CHIKALAKALA CHAKUYAMBA CHA MUSA,
CHIMATANIDWA
GENESIS
1PAKUYAMBA Mlungu adapanga
Kumwamba ndi j iko. 2 Ndi j iko lidali
lotimbilikanya ndi lopanda malile ; ndi
mdima udalipo pamwamba pa nkope ya
vindimba: ndi roho ya Mlungu chiuta-
mile pamwamba pa nkope ya maji.
3 Naati Mlungu, Likalepo dangalila :
ndipo lidakalapo dangalila. 4 Naaliona
Mlungu dangalila, kuti labwino : naapa-
tula Mlungu dangalila ndi mdima. 5 Na-
alitana Mlungu dangalila Usana, ndi
mdima adautana TJsiku. Ndipo udalipo
ujulo ndipo udalipo umawa, siku limoji.
6 Naati Mlungu, Ukalepo mlengalenga
pakati pa maji, chipatulile maji ndi
maji. 7 Naauchita Mlungu mlengalenga,
naapatula maji yayo yadali panchi pa
mlengalenga- ndi maji yayo yadali pa-
mwamba pa mlengalenga : ndipo idalipo
chimwechi. 8 Naautana Mlungu mle-
ngalenga Kumwamba. Ndipo udalipo
ujulo ndipo udalipo umawa, siku la
kawili.
9 Naati Mlungu, Maji yayo yali panchi
pa Kumwamba yakusidwe pa malo pa-
moji, ndi uoneke mtunda : ndipo idalipo
chimwechi. 10 Naautana Mlungu mtu-
nda Jiko; ndi paja maji yadakusidwa
adapatana Zinyanja : naaona Mlungu
kuti ehabwino. 11 Naati Mlungu, Lime-
leche jiko mopo, mmela wakumwazika
mbeu,mtengo wa vipacho wopacha vipacho
kwamtundu wake, uwo mbeu yake mkati
mwake, pamwamba pa jiko : ndipo idalipo
chimwechi. 12 Ndipo jiko lidatulueha
mopo, mmela wakumwazika mbeu kwa
mtundu wake, ndi mtengo wakupacha
vipacho, uwo mbeu yake mkati mwake,
kwa mtundu wake : naaona Mlungu kuti
ehabwino. 13 Ndipo udalipo ujulo ndipo
udalipo umawa, siku la katatu.
14 Naati Mlungu, Ikalepo mienje pa
mlengalenga wa Kumwamba kupatula
usana ndi usiku ; ndipo ikale kwa vizi-
ndikilo, ndi kwa zinyengo, ndi kwa ma-
siku ndi vyaka : 15 ndi ikale kwa mienje
pa mlengalenga wa Kumwamba kumulika
pamwamba pa jiko : ndipo idalipo chi-
mwechi. 16 Naaichita Mlungu mienje
yaikulu iwili ; mwenje wokulu kuulinga-
nicha usana, ndi mwenje wong'ono ndi
ntondwa kuulinganicha usiku. 17 Naa-
ziika Mlungu izo pa mlengalenga wa
Kumwamba kumulika pamwamba pa jiko,
18 ndi kuulinganicha usana ndi usiku,
ndi kupatula dangalila ndi mdima : naao-
na Mlungu kuti ehabwino. 19 Ndipo
udalipo ujulo ndipo udalipo umawa, siku
la kanai.
20 Naati Mlungu, Maji yatutumiche
chotutuma chene umoyo chakulama, ndi
chakuuluka chiuluke pamwamba pa jiko
pamwamba pa nkope ya mlengalenga wa
Kumwamba. 21 Naayapanga Mlungu
mafuni yakulu, ndi chene umoyo chili
chonche chakulama chakuseta, ivo maji
yadavitutumicha, kwa mitundu yao, ndi
chakuuluka chene mapapiko chili chonche
kwa mtundu wake : naaona Mlungu kuti
ehabwino. 22 Naayapacha Mlungu achi-
iwo mwawi, kuti, Mbalane, mchuruke,
ndipo myazaze maji pa nyanja, ndi
chakuuluka ehiehuruke pa jiko. 23 Ndi-
no udalipo ujulo ndipo udalipo umawa,
siku la kasano ndi kamoji.
24 Naati Mlungu, Jiko lituluche chene
umoyo chakulama kwa mtundu wake,
chilangwa, ndi chakuseta, ndi chikoko
cha pa jiko kwa mtundu wake : ndipo ida-
lipo chimwechi. 25 Naachichita Mlungu
chikoko cha pa jiko kwa mtundu wake,
ndi chilangwa kwa mtundu wake, ndi
1. 26—2. 22
GENESIS
chakuseta chili chonche pa ntaka kwa
mtundu wake: naaona Mlungu kuti
chabwino. 26 Naati Mlungu, Timchite
muntu pa chitunjitunji cha ife, kufwana-
na ndi ife : ndi waigwirize nchomba
ya pa nyanja mwendo, ndi chakuuluka
cha Kumwamba, ndi chilangwa, ndi jiko
lonche, ndi chakuseta chili chonche chi-
setacho pamwamba pa jiko. 27 Naampa-
nga Mlungu muntu pa chitunjitunji cha
iye, pa chitunjitunji cha Mlungu ada-
mpanga iye; wamwamuna ndi wamkazi
adawapanga achiiwo. 28 Naawapacha
Mlungu achiiwo mwawi«: naati Mlungu
kwa achiiwo, Mbalane, mchumke, ndipo
mlizaze jiko, mlipondele ; ndipo mgwi-
rize nchomba ya pa nyanja mwendo,
ndi chakuuluka cha Kumwamba, ndi
chintu chili chonche chakulama icho
chisetacho pamwamba pa jiko. 29 Naati
Mlungu, Penya, ndakupachani mmela uli
wonche wakumwazika mbeu, uwo panwa-
mba pa nkope ya jiko lonche, ndi mtengo
uli wonche, uwo uli ndi vipacho va
mtengo mkati mwake wakumwazika
mbeu ; kwa inu siukale kwa chakudya :
30 ndi kwa chikoko chili chonche cha pa
jiko, ndi kwa chakuuluka chili chonche
cha Kumwamba, ndi kwa chintu chili
chonche chakuseta pamwamba pa jiko,
icho chili ndi chene umoyo chakulama
mkati mwake, ndapeleka mmela uli
wonche wowisi kwa chakudya : ndipo ida-
lipo chimwechi. 31 Naachiona Mlungu
chintu chili chonche icho anachichita,
ndipo, penya, chabwino viwi. Ndipo
udalipo ujulo ndipo udalipo umawa, siku
la kasano ndi kamoji.
2 Ndi kudamalizika Kumwamba ndi
jiko, ndi liwanja la.o lonche. 2 Na-
amaliza siku la kasano ndi kawili Mlungu
chotumika chake icho anachichita ; na-
apuma siku la kasano ndi kawili pa
chotumika chake chonche icho anachi-
chita. 3 Naapacha Mlungu siku la
kasano ndi kawili mwawi, naaliika li-
mwelo paloka : chifuko pa limwelo ana-
puma pa chotumika chake chonche icho
anachipanga Mlungu kuchichita.
4 Ivi vibadwa va Kumwamba ndi va
jiko pa kupangidwa kwao, pa siku ilo
Yahveh Mlungu adachita jiko ndi Ku-
mwamba. 5 Ndi chakupuka chili chonche
cha pa dambo sichinakalepo pa jiko, ndi
mmela uli wonche wa pa dambo sunapu-
ke : chifuko Yahveh Mlungu sanavu-
6
mbicha vula pa jiko, ndi padalije muntu
kulima pa ntaka ; 6 nampo chidakwela
chipundulu pa jiko, ndi kuimwecha nkope
yonche ya ntaka. 7 Naamumba Yahveh
Mlungu muntu ndi lifumbi la ntaka, naa-
pumilila pa mpuno zake mpuye wa kula-
ma ; naapata muntu kukala mwene umoyo
wakulama. 8 Naavyala Yahveh Mlungu
munda pa Eden, kuvuma; naamwika
pamwepo muntu uyo adamumba. 9 Na-
apukicha Yahveh Mlungu pa ntaka mte-
ngo uli wonche wakumbika kwa kuonekela,
ndi wabwino kwa chakudya ; mtengo wa
kulama ncho pakati pa munda, ndi mte-
ngo wa kujiwa vabwino ndi voipa.
10 Ndi mchinje udaturuka pa Eden
kuumwecha munda maji ; ndi kuchoka
pamwepo udajipatula, kupata kukala mitu
inai. 11 Jina la wakuyamba Pishon :
umwewo wakulizungulila jiko lonche la
Havilah, pamwepo zahab ; 12 ndipo zahab
ya pa jiko lija yabwino : pamwepo bedo-
lah ndi mwala wa shoham. 13 Ndi jina
la mchinje wa kawili Gihon : umwewo
wakulizungulila jiko lonche la Kush.
14 Ndi jina la mchinje wa katatu Hidde-
kel: umwewo wakuyenda kwa kuvuma
kwa Assur. Ndi mchinje wa kanai Eu-
phrates. 15 Naajitengela Yahveh Mlungu
muntu, naamsiilapo pa munda wa Eden
kuulima ndi kuusunga. 16 Naamtaukila
Yahveh Mlungu muntu, kuti, Va mtengo
uli wonche wa pa munda kudya ujidya :
17 nampo va mtengo wa kujiwa vabwino
ndi voipa, usadya : chifuko pa siku ilo
suudyeko kufa suufe.
18 Naati Yahveh Mlungu, Yosali ya-
bwino muntu akale pa yeka ; sindi-
mchitile wakumtangatila kuanjana naye.
19 Naachiumba Yahveh Mlungu kucho-
kela pa ntaka, chikoko chili chonche cha
pa dambo, ndi chakuuluka chili chonche
cha Kumwamba ; naaja nazo kwa muntu
kuona akadazitana chiani : ndipo lili
lonche muntu adachitana chene umoyo
chili chonche chakulama, limwelo linali
jina lake. 20 Naatana muntu chilangwa
chonche majina, ndi chakuuluka cha Ku-
mwamba, ndi chikoko chili chonche cha pa
dambo ; nampo kwa muntu wosakomanika
wakumtangatila kuanjana naye. 21 Naa-
mgwechela Yahveh Mlungu litulo lakule-
mela pamwamba pa muntu, naagona litulo;
naatenga imoji ya ntiti zake, naacheka-
ncho nyama pa malo pake : 22 naama-
nga Yahveh Mlungu ntiti iyo anaitenga
GENESIS
2. 23—4. 6
pa muntu, kukala wamkazi, naaja naye
kwa muntu. 23 Naati muntu, Uyu
nyengo ii fupa la mafupa yanga, ndi
nyama ya nyama yanga : uyu satanidwe
Muntu Mkazi, chifuko anatengedwa pa
Muntu uyu. 24 Mmwemo muntu samsie
atate wake ndi amake, ndi sakanilile ndi
mkazake : ndipo siwapate kukala nyama
imoji. 25 Niwakala wonche wawili ma-
liseehe, muntu ndi mkazake, ndi wosa-
onana manyazi.
8 Ndi njoka idali yochenjela kupunda
chikoko chili chonche cha pa dambo
icho Yahveh Mlungu anachichita. Naati
kwa wamkazi Kodi Mlungu anati, Si-
mngadye pa mtengo uli wonche wa
munda ? 2 Naati wamkazi kwa njoka,
Tikoza kudyelako vipacho va mitengo ya
pa munda : 3 nampo vipacho va mte-
ngo uwo uli pakati pa munda, adati
Mlungu, Simngadye, simngapapase, mnga-
fe. 4 Naati njoka kwa wamkazi, Kufa si-
mngafe : 5 chifuko Mlungu ajiwa kuti
siku ilo simdyeko, ndipo siyaehekulidwe
maso yanu, ndipo simkale ngati achi-
mlungu, kujiwa vabwino ndi voipa.
6 Naaona wamkazi kuti mtengo udali
wabwino kwa kudya, ndi kuti umwewo
wakukonda pa maso, ndi wokumbika
mtengo kujilingila, naajitengela vipacho
vake, naadya ; naamninkao mwamunake
pamoji naye, naadya. 7 Ndipo maso
ya wonche wawili yadachekulidwa, niwa-
jiwa kuti wali maliseche ; niwasoka ma-
chamba ya mkuyu pamoji, niwajichitila
chakunung'umala. 8 Niwaliva pokoso la
Yahveh Mlungu naayendayenda pa mu-
nda pa nyengo yake mpepo : naabisala
muntu ndi mkazake pa nkope ya Yahveh
Mlungu pakati pa mitengo ya pa munda.
9 Naamtana Yahveh Mlungu muntu,
naati kwa iye, Uli kuti ? 10 Naati,
Ndidaliva pokoso lako pa munda, ndipo
ndidaopa, chifuko ndili maliseche ; ndipo
ndidabisala. 11 Naati, Yani adakuuza
kuti uli maliseche? Kodi unadya va
mtengo, uwo ndidakutaukila kuti usadya ?
12 Naati muntu, Wamkazi uyo udandi-
ninka kukala ndi ine, mmweyo adanini-
nka va mtengo, ndipo ndidadya. 13 Na-
ati Yahveh Mlungu kwa wamkazi, Chiani
ichi udachichita? Naati wamkazi
Njoka * adandinyenga, ndipo ndidadya
14 Naati Yahveh Mlungu kwa njoka
Chifuko udachita ichi, unalesweka kupu-
nda chilangwa chili chonche, ndi kupunda
chikoko chili chonche cha kudambo ; pa
mimba yako suuyende, ndipo lifumbi
suudye masiku yonche ya kulama kwako :
15 ndipo sinditile mawongo pakati pa
iwe ndi wamkazi, ndi pakati pa mbeu
yako ndi mbeu yake : iye sakukotole
mutu, ndi iwe suumkotole chidende.
16 Kwa wamkazi adati, Kuchurukicha
sindichurukiche kupweteka kwako ndi
kuima mimba kwako ; pa vopweteka suu-
pume wana ; ndi kukumbila kwako siku-
kale kwa mwamunako, ndipo iye sakuli-
nganichile. 17 Ndipo kwa muntu adati,
Pakuti unava mau ya mkazako, ndi una-
dya va mtengo, uwo ndidakutaukila, kuti,
Usadya : ntaka yalesweka chifuko chako ;
pa kupweteka suudyepo masiku yonche
ya kulama kwako ; 18 mingancho ndi
chiteji silikupukichile ; ndi suudye mmela
wa munda ; 19 pa chitukuta cha pa
mpuno zako suudye chakudya, mpaka
sudabwelele pa ntaka ; pakuti udatenge-
dwa mmwemo : pakuti lifumbi uli, ndipo
ku lifumbi subwelelencho. 20 Naatana
muntu jina la mkazake Hawa; pakuti
adali amai wa ali yenche wakulama.
21 Naawachitila Yahveh Mlungu muntu
ndi mkazake vakuvinikila va vikwetu,
naawavalika.
22 Naati Yahveh Mlungu, Penya, muntu
anapata kukala ngati mmoji wa ife, kujiwa
vabwino ndi voipa ; ndipo chapano, anga-
tambasule janja lake, ndi kujitengelancho
va mtengo wa kulama, ndi kudya, ndi
kulamila chikalile mmwemoje : 23 ndipo
Yahveh Mlungu adampacha mwanja
achoke pa munda wa Eden, kulima pa
ntaka yapo adatengedwa. 24 Naamtopola
muntu ; naaika A-Kerub kuvuma ku
munda wa Eden, ndi lilime la moto la
upanga wakujilozecha konche konche,
kuisunga njila ya mtengo wa kulama.
CHIKALAKALA CHOYEEA
NDICHO
MALANGANO YA KALE
NDI
MALANGANO YA CHAPANO
LONDON
BKITISH AND FOREIGN BIBLE SOCIETY
1912