Translation of the Meanings of
THE NOBLE QURAN
in the Chichewa Language
— „,
&mm&\\mm
Myang'aniri wa Mizikiti iwiri Yolemekezeka
Mfumu Fahd Bin Abdul 'Aziz Al Saud, Mfumu ya
Saudi Arabia ndi okondwa polamula kusindikiza
Buku la Qur'an lotanthauzidwa
,„ „->. , ,■„„ , . m"^;^;^;^^^
Nyumba ya Mfumu Fahd
yosindikizira Qur'an yopatulika
**~~~~~~ ~» „ , ..„.. ...,„ , ,_^ ., , ^
7*-y£j\ Jt X+^*J* /wi ^jyJ|JL*P V,J ?JL^ ye.j.>t-'l <Jb^ *-*£»
^L-ijVlj 5j_pjJ!j cJUjVlj i-w.^L— y\ oj3_^JI yjj
: ^1 <ol^ J J3UJI 4 o*iWI VJ & JuJ " 1
: J3UJI 4 ju^ L~j t cA-^b *-W»^' ^->j-^f ^ fM-Jlj stA^JIj
. «<uApj oljiJl (J~ j>« ^^»
rjbuU
4 aj^*-«JI a-jj-«JI a£LJlL ^LijVlj S^jJIj cJUjVlj i-^^^L- »Vl jjj-iJI Sjljj ^ Ulclj
^JL.Al ^jip a^^jI ^>L^ j 4 4 4»$ll oL*AM ^-*-=r ^1 ' /O^' of^iM ^ L«^ ^-^>-y ^c-**^
. «4jI _jJj ^^p iyJL» : ||£ ^Jy ^ <j j^lil f!)LiJ U^j 4 A^yJl ^ ^j^Ul
^jjjJLJI <Jbt-s*il ipUJ JL$J ciJULil *l*_£ k-.Jbj 4 l^-JLj-iJl oJL. j^iktJ! LjI^'V ^L«Jl>-j
*-jA^I jjl>- ^jjl UJLfrf ^1 4 lj.JLJL3l <iL 4-aj^jJI oJL* r^l &jUJU ^JLL jf 4 5jyil ioJlL
. Lojy JU^»t« ^-~*^ ^-iJlj 4 Vl-Ul ^*p Aiil-UP ^-JJl £-*Jrl JJ ^ I^a^-Ijj 4 NIij
. ^Ul <J *uLj (jfj 4 £^3l <p-^
^yUil *.bf ^p 0j-vtf»l5 Oj^— » -Lfiw OviL L^j- £^^-Jl olyjJl ^ L»oo i^-jS of iij-xJ LjI
L. iLva^ ^ Irl 4-^j-yJI l^.^ ^yJl ^iUil ofj 4 jj^t cyLr^ 1 <J^* WJ^ J-^i <>Jl A-^JajJt
. ^^aij lla>- J^ 4K j-lJl J^P ^^Uj U l^ijiM <ifj 4 ^^1 4JAI ^jllS" ^3 ^ ^j^l pi* <iL
i^Jjj-tJi t*_ipfcsdll ipUaJ Xp kiUil ^*J>t^ ^'^d «jf <*>-jZ}\ o-lgJ ^jl5 JS" ^ y>-J> Ji j^j
^ oL^lj-J^—»Vi oJL* ^a o^Li^U 4 o^Lij jf ^^tfii jf Ua>- ^ \ g J o-L>tj JLi lr Aj^-jJI AJu jlLL
. ajiif *.Li ol i»^UJl cj^AiJI
Ill
BISMILLAH RAHMAN RAHIM
MAU OYAMBA
Wolemba: Wolemekezeka Sheikh
Saleh Bin Abdul Aziz Bin
Muhammad Al al-sheikh,
nduna ya zachisilamu, chuma
chopelekedwa mnjira ya mulungu,
dawah ndi kutsogolera ku njira
yoongoka, ndiponso wankulu
woyang'anira nyumba yosindikizira.
Kutamandika konse ndi kwa Mulungu bwana wa
zolengedwa zonse, amene adanena m'buku lake
lolemekezeka kuti: "Kwakufikani inu kuchokera kwa
mulungu kuwunika ndi buku lofotokoza chilichonse "ndipo
chipulumutso ndi mtendere zikhale kwa olemekezeka wa
aneneri ndi atumwi onse, mthenga wa mulungu
Muhammad amene adanena kuti; " wabwino mwa inu ndi
amene waphunzira Qur'an ndi kuiphunzitsa".
Pambuyo pake:
Pofuna kukwaniritsa malangizo a wotumikira wa malo
awiri olemekezeka ndiponso oletsedwa mfumu Fahd
Abdul Aziz Al Saudi,Mulungu amusunge chifukwa
chakuliganizira buku la Mulungu, ndikugwira ntchito
yolifewetsera njira yofalitsira, ndikuligawa kwa Asilamu
onse kuyambira kum'mawa ndikumadzulo kwa dziko
lonse, kulifotokozela ndi kulimasulira kwake mzinenero
zosiyana-siyana mdziko lonse, ndiponso ndichikhulupiriro
cha unduna wa zachisilamu, chuma chopelekedwa mnjira
ya Mulungu, dawa ndi kutsogolera kunjira yoongoka
m'ndziko la Saudi Arabia, mwakufunika kwa kumasulira
matanthauzo a Qur'an yolemekezeka mzinenero zonse
zofunika za dziko lonse, ndi cholinga choti Asilamu onse
omwe chinenero chawo si chiarabu, ndikufunitsitsa
kufalitsa komwe mtumiki adalamula kuti: "falitsani zaine
ngakhale ndime imodzi yokha".
IV
Ndipo pofuna kuwathandiza abale anzathu omwe
amalankhula chinenero cha Chichewa, a Nyumba
yosindikiza buku lolemekezeka la Qur'an ya mfumu
Fahd ku Madinah Munawwarah, ali osangalala
kupeleka kwa wowerenga wolemekezeka tanthauzo la
bukuli m'chichewa lomwe anamasulira Sheikh Khalid
Ibrahim ndipo analiona kumbali ya nyumbayi Sheikh
Abdallah Omar Issa Mdala mothandizana ndi Sheikh
Shaib Muhammad Mzoma.
Choncho tikuyamika Mulungu wapamwamba-mwamba
povomereza kuti ife tithe kugwira ntchito yaikuluyi
yomwe tikulaka-laka kuti ikhale mwachifuniro cha
Mulungu yekhayo ndikutinso anthu athandizike nayo.
Ife tikudziwa kuti ntchito yomasulira matanthauzo a
Qur'an yolemekezeka, ngakhale ikongole chotani,singafanane
ndi matanthauzo eni-eni a Qur'an ya m'charabu
yozizwitsa, ndikutinso matanthauzo omwe akumveka
mukumasuliraku ndi olingana ndi m'mene kuliri kuphunzira
kwa omasulira wake polimva Buku lolemekezeka la
Mulungu, ndikutinso monga munthu wina aliyense,
ntchitoyi singakhale yopanda kulakwitsa ndi kupunguka,
Choncho tikupempha kwa wowerenga wina aliyense
amene angazindikire zolakwika, kupunguka kapena
kuonjezera kuti aidziwitse nyumba yosindikizira buku la
Qur'an ya mfumu Fahd yomwe ili ku Madinah
Munawwarah. Izi zizakhala zothandiza posindikizanso
bukuli mtsogolo Mulungu akafuna.
Mulungu ndiye wothandiza ndiponso muwongoli kunjira
yoongoka. Ambuye Mulungu tilandireni ife ndithudi inu
ndinu wakumva wodziwa.
V
M'dzina la Mulungu Wachifundo chambiri Wachisoni
MAWU A OTANTHAUZIRA QUR'AN
Kuyamikidwa konse ndi kwa Mulungu, Mbuye wa zolengedwa.
Madalitso ndi mtendere zikhale pa Mtumiki Muhammadi (S.A.W),
akubanja lake ndi onse omutsatila.
Qur'an ndi mawu a Mulungu amene adavumbulutsidwa kwa
Mtumiki Muhammad (S.A.W), omwe sadasinthidwe chiganizo kapena
lemba lirilonse ngakhale pang'ono ndipo idzasungidwa chomwecho
mpaka tsiku la Chimaliziro.Mulungu wapamwamba walichita buku
lakeli kuti likhale uthenga wotsiriza wochokera kumwamba.
Adalivumbulutsa kwa Mtumiki womaliza Muhammad yemwe ndi
Mtumiki wankulu kuposa atumiki onse a Mulungu amene adadza ndi
uthenga wochokera kumwamba.
Mulungu adatumiza kwa anthu atumiki wocthedwa
MURSALINA, munyengo yosiyanasiyana, m'mayiko osiyanasiyana,
ndiponso kumibadwo yosiyanasiyana. Maina ena a atumiki ndi awa:
Adam. Nuhu, Ibrahim, Ishaka, Yaaqub, Yusuf, Musa, Daudi,
Sulaiman, Yahya, ndi Isa (Yesu)
Tsono ena mwa iwowa, adawavumbulutsila mabuku ake. Komatu
uthenga wa mabukuwa udali wopita kumtundu wawo kapena ku
m'badwo wawo wokha osati kwa anthu onse. Pachifiikwa chimenechi,
uthengawu udaonongedwa ndi maganizo a wanthu poonjezera ndime
zina ndi kuchotsa ndime zina zimene ankaziona kuti sizikuyenerana
ndi nthawi yawo ndi m'badwo wawo. Ndipo mabuku ena amene
wanthu akuwatcha kuti adavumbulutsidwa ndi Mulungu , kuchokera
kumwamba, wanthu amenewa sangathe kusonyeza umboni woona
kuti ndi ziganizo ziti za ndime zimene zidavumbulutsidwa kumwamba
ndi zimene zidaonjezedwa pambuyo pake munthawi yosiyanasiyana.
Pakuti mabukuwo Mulungu adawavumbulutsa kuti athandize
panthawi yokhayo.
Itatha nthawiyo adawalekerera sadawasunge kuti asasokonekere.
"Koma Qur'an, yolemekezeka adaivumbulutsa kwa Mtumiki
wotsiriza yemwe sipanatumizidwe pambuyo pake Mneneri ngakhale
Mtumiki, kuti likhale Buku la anthu onse. Chifukwa chakuti
sikudzabweranso Mtumiki wina. Ndipo adakwaniritsa ndi buku
lopatulikali Chipembedzo Chake Choona. Ndipo adakwaniritsa ndi buku
lakeri Chisomo chake pa wanthu ake onse ndipo adalichita kukhala
chiongoko ndi kuunika mpaka pa tsiku lomaliza,"
VI
Mulungu adalonjeza kuti adzalisunga buku lakeli (laQur'an)
sipadzachotsedwa lemba kapena kuonjezera lemba ndiponso
sipadzatheka kuonekamo zolakwika kapena kutsutsana ndi mabuku
akale.
Buku ili la Qura'n limene tili naloli, limene lafala pa dziko lonse la
pansi tikhoza kunena motsimikiza kuti ndiwo mawu a Mulungu
Wapamwambamwamba adawavumbulutsa kwa Mtumiki wake
Muhammad (S.A.W) muzaka mazana khumi ndi anayi zapitazo.
Monga adalonjeza kulisunga buku Lakeli, lidzasungidwabe
mpaka kutha kwa dziko la pansi Ndipo mu ndime ya 9 ya Surati Hijiri
Mulungu wanena kuti. "Ndithudi ife ndi amene tauvumbulutsa
ulalikiwu (Qura'n iyi) ndipo ife ndi amene tidzausunga.
Mwatsoka, anthu akukhulupirira kuti Chisilamu tsopano ndi
Chipembedzo cha ASilamu okha. Ndipo Qur'an ndi buku lopatulika la
Asilamu okha. Alinso ndi chikhulupiriro chakuti Muhammad ndi
Mtumiki wa Asilamu okha muongoli wawo osati wa anhtu onse.
Kudza ndi ganizo ili ndi kulifalitsa, kunachitika ndi anthu omwe
sadali Asilamu. Adachita izi chifukwa chakunyansidwa chabe ndi
chipembedzochi kapena kusadziwa mokwanira za chipembedzochi.
Mulungu wapamwambamwamba akunena m'buku lake lomaliza kuti
Muhammad (madalitso a Mulungu ndi mtendere wake zikhale pa iye)
sadali ngati atumiki amene adatsogola, chifukwa chakuti iye yekha
ndi amene adamtuma kwa anthu onse, kumitundu yonse, kumakungu
onse oyera ndi akuda. Mundime ya 158 ya Surat Al-A'raf, Mulungu
wanena kuti. "Nena (iwe Mneneri Muhammad) E, inu anthu !
Ndithudi ine ndi Mtumiki wa Mulungu kwa inu nonse, Mulungu
yemwe ndi mwini ufumu wakumwamba ndi pansi, palibe
wopembedzedwa mwachoonadi koma iye yekha. Iye ndi yemwe
amapeleka Moyo ndi Imfa.
Choncho mkhulupirireni Mulungu ndi Mtumiki Wake yemwe ali
Mneneri Ummiyyu (wosadziwa kuwerenga ndikulemba) yemwe
akhulupirira Mulungu ndi mawu ake Ndipo mutsatireni iye kuti
mukhale oongoka."
Kunena motsimikiza Asilamu akuyetsetsa kukwaniritsa udindo
wawo popereka umboni woona ndikufalitsa kwa anthu onse.
Chisilamu sichidadze kwa anthuakuti akuti kapena mtundu
wakutiwakuti koma chidadza kwa anthu ndi mitundu yonse ya
padziko lapansi .Tsono chatsalira kwa amene akufuna kudziwa
VII
choonadi, ndikuti achifunefune powerenga Qur'an ndikumvetsetsa
uthenga wake wa Mulungu omwe ukupezeka mkati mwake, chifukwa
chakuti Qur'an ndi mphatso ya uzimu imene apatsidwa anthu onse ndi
Mulungu.
Qur'an ikulankhula ndi anthu onse. Qur'an ndi uthenga wa
Mulungu kwa anthu onse, kuti anthuwo apeze mtendere wa muyaya.
Uthenga wa Mulunguwu , ukuyikira umboni ndikutsimikizira
mauthenga onse amene Mulungu adawabvumbulutsira aneneri ake
kuyambira Mtumiki Adamu mpaka Isa (Yesu) ndipo Qur'aniyi
ikukwaniritsa uthenga Wake.Choncho uthenga wa Mulungu
wakwanira ndi buku lomaliza ndi Mtumikinso uyu womaliza
Arabu ndi anthu oyamba amene idawalankhula Qur'an, kotero kuti
Qur'an idabvumbulutsidwa n'chilankhulo cha Chiarabu, pambuyo
pake idamasulidwa mzilankhulo zosiyanasiyana. Adauzidwa Msilamu
aliyense kuti agwire ntchito molimbika pofikitsa uthenga
wachoonadiwu kwa anthu onse pano padziko lapansi. Ndipo Hisitole
(mbiri yakale ) ikuyikira umboni kuti Asilamu adakwaniritsa udindo
umenewu moyenerana. Adaufikitsa uthenga wa Mulunguwu mbali
zonse padziko lonse lapansi. Adamasulira matanthauzo a Qur'an
muzilankhulo zosiyanasiyana zimene zidali zodziwika nthawi
imeneyo kuti anthu apeze phindu ndi malangizo amene akupezeka
mQur'an makamaka amene sakudziwa chilankhulo cha Chiarabu kuti
atsatire malamulo ake ndikuzipewa zimene yaletsa Kunena
mwatsatanetsatane, buku limeneli ndi lofunika ku mtundu wa anthu
chifukwa chakuti muli zonse zofunika pamoyo wamunthu; m'mene
angakhalire payekha kapena ndi anzake ;m'mene angagwirire ntchito
yake yomuthandiza pano padziko lapansi kapena pa tsiku
lachimaliziro. Ndipo Munthu amene awerenga bukuli natsatira
zophunzitsa zake, limuongolera ndi kumuunikira njira ya choonadi
Sura yoyamba ndi surati Fatiha. Ndipo sura yotsiriza ndi surati
Nasi. Mulungu adalibvumbulutsa bukuli kwa womaloza mwa aneneri
ake kuti likhale buku lomariza kwa anthu ake onse,lomwe mkati
mwake muli maphunziro othandiza anthu kuti apeze mtendere pano
padziko la pansi ndi tsiku lachimaliziro. Ndime zake zidatsika
mosiyanasiyana malingana ndi zinthu zomwe zinkachitika m 'nthawi
ya zaka (23) makumi awiri ndi zitatu za uneneri Wake Muhammad
(S.A.W)
Gawo Una lidatsika iye akukhala mu mzinda wa Makka. Ndipo
lina lidatsika atasamukira ku Madina. Sura zomwe
VIII
zidabvumbulutsidwa ku Makka zimafotokoza maziko a
chikhulupiliro, monga kukhulupilira Mulungu, Angelo, Mabuku,
Aneneri ndi tsiku lachimaliziro. Tsono sura zomwe
zidabvumbulutsidwa ku Madina zimafotokoza malamulo a
chipembezochi. M'Qur'an mukupezeka nkhani zakale ndiponso
mukupezeka nkhani za kutsogolo.
KUTANTHAUZIRA QUR'AN M'CHICHEWA
Chifukwa chakufunika kwa uthengawu kuti ufike kwa anthu onse,
a Bungwe la Africa Muslim Agency adandipempha kuti ndimasulire
Qur'an m'chichewa, ndicholinga chakuti amene sangathe kumvetsa
uthenga wake m'chiarabu, aumve m'chilankhulo chawo cha
Chichewa. Choncho ntchitoyi idagwirikadi kotero kuti munthu
akawerenga bwinobwino akhoza kumva uthenga wa Mulungu
m' Qur'an. Ndayetsetsa m'kutanthauzira kwanga mawu oyerawa kuti
musakhale zolakwika zambiri, koma ntchito yogwira Munthu
siilephera kupezeka zolakwika kupatula zochita za Chauta. Munthu
ndi Munthu basi.Choncho ndikupempha aliyense amene angapeze
zolakwika pakatanthauzidwe ka Qur'an kapena kasankhidwe kamawu
oyerawa, kuti anditumizire ndi cholinga choti pomazatuluka bukuli
kachiwiri muzakhale mopanda zolakwika zimenezo
Pamene ndimagwira ntchitoyi, panali mabuku amene
ndimathandizika nawo pakasankhidwe ka kutanthauzira koyenera kwa
Qur'an, komanso anthu amene amandithandiza pakasankhidwe ka
mawu oyenera m'chichewa. Mabukuwa ndi awa Tafsiri ya Jalalain,
Tafsiri ya Ibn Kathiri, Al Muntakhab ndi Swafuat Tafaasiri. Ndipo
Ntchito yotanthauzira inatha m'chaka cha 1987 pambuyo poigwira
mzaka zitatu. Ndipo kuyambira nthawiyo kufikana m'chaka cha 1999
yakhala ikuunikidwandi ma Sheikh akuluakulu m'dziko muno.
Tikupempha Mulungu kuti ntchito imene tagwirayi, ailandire
ndipo akatipatse mphoto yake pa tsiku lachimaliziro. Tikupemphanso
kuti bukuli alichite kukhala lolandiridwa ndi anthu onse, ndipo kuti
apereke madalitso kwa onse amene anathandiza kuti bukuli lituluke.
Ine M'bale Wanu
Sheikh Khalid Ibrahim
P.O BOX 60166
Blantyre
MALAWI
■ ,, ,„-,, ,-i.r,^,
QUR'AN
YOLEMEKEZEKA
yotanthauzidwa
m'chichewa
Nyumba ya Mfumu Fahd
yosindikizira Qur'an yopatulika
Surat 1. AI-Fatihah Juzu 1
> *>i
) a£\A\ djj-*»
Surat Al-Fatihah I
Wfmm& M
1. M'dzina la Mulungu
Wachifundo Chambiri, Wachisoni.
2. Kutamandidwa konse nkwa
Mulungu Mbuye Wa zolengedwa
zonse.
3. Wa chifundo chambiri, Wa
chisoni.
4. Mwini tsiku lachiweruzo.
5. Inu nokha
tikukupembedzani, ndiponso Inu
nokha tikukupemphani
chithandizo.
6. Tiongolereni kunjira
yoongoka.
7. Njirayaomwe
mudawapatsa chisomo; Osati ya
amene adakwiyiridwa (ndi Inu)
Osatinso ya omwe adasokera
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1 2 ^ ^' * OjiJi 3jj-»
SURAT AL-BAQARAH II
££&&
Iyi ndi imodzi mwa sura zomwe zinavumbulutsidwa ku
Madina pambuyo pakuti Mtumiki (Mtendere ndi madalitso a
Mulungu zikhale naye) atasamuka ku Makka.
Iyi ndi sura yaitali kwambiri m' Qur'an (Msafu) yopatulika
malinga ndi m'ndondomeko wa sura.
Surayi yafotokoza mwatsatanetsatane zomwe Surat Fatiha
yafotokoza mwachidule. Ndipo ikuti Qur'an ndilo gwero la
chiongoko, chilungamo. Ndipo yakambanso za Qur'an, chiyanjo
cha Mulungu ndi amene Mulungu adawakwiyira. Ndipo
ikunenetsanso za Qur'an kuti njoona ndi kuti malangizo ake
ngoona okhaokha; mulibe chilichonse chokaikitsa. Kenako
yapitirira nkumafotokoza kuti anthu, kumbali ya uthenga wa
Qur'an, adali m'magulu atatu. Gulu loyamba ndilo lokhulupirira
Mulungu kudzanso zinthu zosaoneka ndi maso. Hi ndilo gulu
lopambana. Gulu lachiwiri ndilomwe lidakana Mulungu ndi
kutsutsa zinthu zonse zosaoneka ndi maso. Hi ndilo gulu lotaika.
Gulu lachitatu ndilo gulu la achiphamaso lomwe
linkakhulupirira Mulungu ndi Mtumiki (madalitso ndi mtendere
wa Mulungu zikhale naye) ndi pakamwa chabe pomwe
m'mitima mwawo mudalibe chikhulupiriro.
M'suramu mwafotokozedwa malamulo ambiri pa
chikhulupiriro, mapemphero, malonda, makhalidwe abwino,
kumanga ndi kulekana ukwati, eda, ndi kulemba ngongole ndi
malamulo ena ambiri onena za chipembedzo cha Chisilamu.
Ndipo yapitiriza kufotokoza zachiyambi cha mtundu wa
munthu, potchula nkhani ya Mneneri (Adamu) yemwe ndikholo
lamtundu wa munthu, ndi momwe adapezera ulemu kwa Angero
ndi zina zonse zimene zinamchitikira, pamene satana
adamunyenga. Ndipo surayi yafotokozanso mwatsatanetsatane
makamaka za ana a Israyeli poti iwo adakhalira limodzi ndi
Asilamu mu mzinda wa Madina. Ndipo surayi ikuchenjeza
Asilamu kuti achenjere ndi Ayuda omwe nthawi zonse
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1 3 > ^jk-\ T o^aJi Sj^
chikhalidwe chawo nkukonda ziwembu, chinyengo, kuswa
mapangano ndi zina zoipa kwambiri.
M'suramu mulinso malamulo a Swaumu (kumanga), Haji,
ndi kuchita Jihadi panjira ya Mulungu. Ndipo yafotokozanso za
kuipa kwa malonda akatapira, pochenjeza kuti amene achita
malondawa ndiye kuti akumenyana ndi Mulungu ndi Mtumiki
wake.
Kothera kwake surayi, yaalangiza Asilamu kuti azichulukitsa
mapemphero, ndi kulapa kwa Mulungu.
Surayi ikutchedwa "Baqara" pokumbutsa chozizwitsa
chachikulu chomwe chidachitika m'nthawi ya Mneneri Musa
pamene adaphedwa munthu wa mtundu wa Aisiraeli. Amene
adamupha sadadziwike. Choncho, adakasuma kwa Musa kuti
mwina iye angamzindikire wakuphayo. Ndipo Mulungu
adamzindikiritsa Musa kuti awalamule kuti aphe ng'ombe
yaikazi ndi kuti amkwapule wakufayo ndi gawo lina la
ng'ombeyo potero auka mwachifuniro cha Mulungu nkuwauza
yemwe adamupha. Ndikutinso chimenechi chikhale chisonyezo
chakukhoza kwa Mulungu kuukitsa anthu ku imfa. Potero surayi
idatchedwa Surat Baqara, (sura yang'ombe).
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1
> frjfcl
t S^iJl 5jj«-
Surat Al-Baqarah II
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Alif-Ldm-Mim}
2. Hi ndi Buku lopanda
chipeneko mkati mwake; Ndi
chiongoko cha (anthu) oopa
Mulungu.
3. Omwe amakhulupirira
zosaoneka ndi maso (Monga
Munda wa mtendere, Moto,
Angero. Ndi zina zotere zomwe
Mulungu ndi Mtumiki
Adazifotokoza), amapemphera
Swala moyenera, Ndiponso
amapereka m'zimene tawapatsa;
4. Ndi amene akukhulupirira
zomwe zidavumbulutsidwa kwa
iwe, ndi zomwe
zidavumbulutsidwa kale iwe
usadadze Nakhulupiriranso
(motsimikiza) kuti Lilipo tsiku
lomaliza.
*^ii^-
q^i^jii^U-
Jb
©JSJI
®iffltfb&2$<^
jjliliy^jc^L^S^i
®fcS^Sfe»
Sura iyi yayamba ndi malembo a Alifabeti, monga A.L.M. kusonyeza kuti
Qur'an yalembedwa ndi malembo amenewa omwe anthu amawagwiritsa
ntchito m'zoyankhula ndi m'zolembalemba zawo. Uku ndikuuza osakhulupirira
kuti abweretse buku iawo lolembedwa ndi malembo omwe akuwadziwawo
pamene iwo amanena kuti Qur'an adangoipeka yekha Muhamadi (SAW)
siidavumbulutsidwe ndi Mulungu. Choncho Mulungu adawatchalenja kuti
alembe buku Iawo lofanana ndi Qur'an, koma adalephera, ndiponso
ikufotokoza za chikhalidwe cha anthu olungama.
Choncho, kulephera kwawo ndi umboni wosonyeza kuti Qur'an ndi buku
lovumbulutsidwa ndi Allah.
Surat 2. AI-Baqarah Juzu 1
1 *>i
t djiJi djj--»
5. Iwowo (omwe ali ndi
chikhalidwe chotere), ali
Pachiongoko chochokera kwa
Mbuye wawo, Ndipo iwowo ndi
omwe ali opambana (Pokapeza
ulemerero wapamwamba ku
Minda ya mtendere).
6. Ndithu amene sadakhulupirire,
nchimodzimodzi kwa iwo
uwachenjeze kapena
usawachenjeze Sangakhulupirire.
7. (Ali ngati kuti) Mulungu
wawadinda Chidindo chotseka
mitima yawo ndi makutu awo
(kotero kuti kuunika kwa
Chikhulupiriro sikungalowemo),
ndipo M'maso mwawo muli
chophimba (sangathe Kuona
zozizwitsa za Mulungu); Choncho
iwo adzalandira chilango chachikulu.
8. Pakati pa anthu alipo (anthu
achinyengo) Amene akunena:
"Takhulupirira mwa Mulungu ndi
tsiku lomaliza," pomwe iwo Sali
okhulupirira.
9. Akufuna kunyenga Mulungu
ndi amene Akhulupirira, ndipo
sanyenga aliyense koma okha,
ndipo iwo sazindikira (kuti
Akudzinyenga okha).
10. M' mitima mwawo muli
matenda; ndipo Mulungu
wawaonjezera matenda. Choncho
Iwo adzalandira chilango
chopweteka chifukwa chakunena
kwawo zabodza.
Itfyt*
** ii-r <K \
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1
^ * >»
Y dyLS\ Ojj*>
11. Ndipo akauzidwa kuti,
"Musaononge padziko,"
amayankhakuti: "Ife ndife
okonza."
12. Dziwani kuti, ndithudi, iwo
Ndiwo ali oononga (padziko);
Koma sakuzindikira.
13. Ndipo akauzidwa kuti,
"Khulupirirani monga momwe
anthu ena akhulupirira,"
akuyankha Kuti, "Kodi
tikhulupirire monga momwe
Zakhulupirira zitsiru?" Dziwani
kuti, ndithudi, iwo ndi omwe ali
zitsiru, Koma sakudziwa.
14. Ndipo akakumana ndi
amene akhulupirira, amanena,
"Takhulupirira." koma akakhala
Paokha ndi asatana awo, amati:
"Ndithudi, Ife tili pamodzi nanu.
Timangowachita chipongwe basi."
15. Mulungu adzawalipira
chipongwe chawocho.
Ndikuwalekerera
akungoyumbayumba (Kugwira
njakata) m'kusokera kwawo.
16. Oterewo ndi omwe
asinthanitsa chiongoko ndi
kusokera, koma malonda awo
sadawapindulire Chilichonse, tero
sadali oongoka.
17. Fanizo lawo
(achinyengowo) lili ngati (Anthu
*€$&&£&$&;
fi^K
Surat 2. AI-Baqarah Juzu 1
) *>i
T *j*J\ tjj*'
apaulendo afungatiridwa Ndi
chimdima) omwe ayatsa moto;
ndipo Pamene udaunika zomwe
zidali M'mphepete mwawo,
Mulungu Nkuwachotsera kuunika
kwawoko nawasiya Mumdima
osatha kuona.
18. (Nakhala ngati) agonthi,
abubu, Akhungu; ndipo
sangabwererenso
(Kuchiwongoko).
19. Kapena (fanizo lawonso)
lili ngati chimvula Chochokera
kumitambo m'kati mwake
Muukhala mdima, mphenzi ndi
kung'anima, Naika zala zawo
m'makutu mwawo chifukwa
Chamkokomo ndikuopa imfa
(pomwe kutero Sikungawathandize
chilichonse). Ndipo Mulungu
akudziwa bwinobwino za
Osakhulupirira.
20. Kung'anima kukuyandikira
kutsomphola Maso awo; nthawi
iliyonse kukawaunikira, Nkuyenda
m'menemo (mkuunikamo). Koma
Kukawazimira, nkuima. ndipo
Mulungu akadafuna
akadawachotsera kumva kwawo
Ndi kuona kwawo. Ndithudi,
Mulungu ngokhoza chilichonse.
21. E inu anthu! Pembedzani
Mbuye wanu yemwe adakulengani
inu ndi omwe adalipo kale, kuti
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1
8
\ *>■»
t ljL3\ 5jj->
mudzichinjirize (ku chilango cha
Mulungu).
22. (Mulungu) yemwe
adakupangirani Nthaka kukhala
ngati mphasa, ndi thambo Kukhala
ngati denga; ndipo adatsitsa Madzi
kuchokera kumitambo natulutsa
ndi madziwo, zipatso
zosiyanasiyana kuti chikhale
chakudya chanu. Choncho
Mulungu musampangire anzake
Uku inu mukudziwa (kuti alibe
Wothandizana naye).
23. Ndipo ngati muli ndi
chikaiko m'zomwe
Tamvumbulutsira kapolo wathu
(Kuti sizinachokere kwa Ife, koma
wangopeka Yekha) tabweretsani
sura imodzi Yolingana ndi
Quraniyi (m'kayankhulidwe ka
nzeru Ndi kayalidwe ka malamulo
ake). Ndipo itanani athandizi anu
(kuti akuthandizeni) kupatula
Mulungu; ngati Inu mukunena
zoona (kuti Qur'an Njopekedwa).
24. Choncho ngati simutha
(kubweretsa sura imodzi yonga ya
m'Qurani) ndiye kuti Simudzatha.
Choncho opani moto omwe
Nkhuni zake ndi anthu (okanira)
Ndi miyala (yamafano) umene
wakonzedwera kwa
Osakhulupirira.
25. Ndipo auze nkhani
yabwino amene akhulupirira
®&m&>!&Q&
<&L5
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1
1 *>»
Y SjiJl 5jj--
nachita ntchito zabwino
(Molungama) kuti ndithu
adzalandira minda ya Mtendere
momwe mitsinje ikuyenda pansi
pake ndi patsogolo pake. Nthawi
iliyonse kumeneko akapatsidwa
zipatso Ngati chakudya, adzakhala
akunena: "Izi ndi zomwe
tidapatsidwa kale," (Chifukwa
chakuti) adzapatsidwa zipatso
zofanana (m'maonekedwe ake Ndi
zimene adapatsidwapo kale. Koma
makomedwe ake ngosiyana).
Ndiponso Akalandira m'menemo
akazi oyeretsedwa (Kuuve
wamtundu uliwonse); ndipo Iwo
adzakhala m'menemo muyaya.
26. Ndipo Allah sachita
manyazi kuponya Fanizo la
udzudzu ndi choposerapo (Pa
udzudzu). Koma amene
Akhulupirira akuzindikira kuti
(Fanizolo) ndi loona ndi lochokera
mwa Mbuye wawo. Koma amene
Sadakhulupirire, akunena: "Kodi
Allah akufuna chiyani Pafanizo
lotereli?" (Allah) Amawalekerera
ambiri kusokera ndi Fanizo lotere,
komanso amawaongola ambiri ndi
fanizonso lotere. Komatu
sawalekerera kusokera nalo
Kupatula okhawo opandukira
chilamulo (chake);
27. Omwe akuswa chipangano
cha Allah pambuyo pochimanga
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1
10
\ *>i
Y SjiJl 3jj^
(kuti adzachikwaniritsa;
ndikutsatira Malamulo a Allah),
ndiponso amadula (Chibale)
chomwe Mulungu adalamula kuti
chilumikizidwe, naononga padziko
(Poyambitsa nkhondo ndi
ziwawa); Iwowo ndi amene ali
otayika.
28. Kodi mungamkane chotani
Allah chikhalirecho inu mudali
akufa Ndipo Allah adakupatsani
moyo (Nakuikani padziko
lapansi)? Kenako Adzakupatsani
imfa (ikakwana nthawi Yanu
yofera). Kenako adzakuukitsani
(Ndikukutulutsani m'manda).
Ndipo Kenako mudzabwezedwa
kwa lye (kuti Mukaweruzidwe
pazomwe mudali kuchita).
29. lye ndi Yemwe
adakulengerani Zonse m'dziko
lapansi, kenako adalenga Thambo
nakonza thambo zisanu ndi Ziwiri.
lye Ngodziwa chinthu Chilichonse.
30. Akumbutse (anthu ako
nkhani iyi) Panthawi yomwe
Mbuye wako anati kwa Angelo:
"Ine ndikufuna kuika Mdziko
lapansi wondiimirira." (Angelo)
adati: "Kodi muika m'menemo
amene Adzidzaonongamo ndi
kukhetsa mwazi, Pomwe ife
tikukulemekezani ndi
Kukutamandani mokuyeretsani?"
(Allah) Adati: "Ndithudi, Ine
% {
9? WZ
ua
S 19 * 9»
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1
11
> *>i
t SjiJl Ojj^>
ndikudziwa Zimene
simukuzidziwa."
31. Ndipo (Allah) adaphunzitsa
Adam Mayina a (zinthu) zonse;
Nazibweretsa (zinthuzo) pamaso
pa Angelo, Naati (kwa Angelo):
"Ndiuzeni Mayina a zinthu izi
ngati mukunena Zoona (kuti inu
ndinu ozindikira Zinthu)?"
32. (Angelo) adati:
"Kuyeretsedwa nkwanu! Ife tilibe
kuzindikira kupatula chimene
Mwatiphunzitsa. Ndithudi, Inu
Ngodziwa Kwambiri, Anzeru
zakuya."
33. (Allah) adanena: "E iwe
Adam! : Auze Maina ake." Ndipo
pamene adawauza Mayina ake,
(lye) adati: "Kodi Sindinakuuzeni
kuti Ine ndikudziwa Zobisika
zakumwamba ndi pansi, ndiponso
Ndikudziwa zimene mukuonetsera
poyera Ndi zimene mukubisa?"
34. Ndipo (akumbutse anthu
ako nkhani iyi) Pamene tidawauza
Angelo: "Mgwadireni Adam."
Onse adamugwadira Kupatula
Iblisi (Satana); anakana
Nadzitukumula. Tero adali
m'modzi Mwa osakhulupirira.
35. Ndipo tidati : "E iwe
Adam! Khala iwe Ndi mkazi wako
m'mundamo (mu Edeni); Idyani
m'menemo motakasuka paliponse
®,^ ; W'
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1 12 S sjA-i
T S^iJl 5jj-»
Pamene mwafuna; koma
musauyandikire Mtengo uwu
kuopera kuti mungakhale Mwa
oipa (odzichitira okha zoipa)."
36. Koma Satana (Iblisi yemwe
uja) Adawalakwitsa onse awiriwo
(nanyoza Lamulo la Mulungu
ndikudya mtengo Woletsedwawo),
nawatulutsa mu Mtendere momwe
adaalimo. Ndipo Tidawauza:
"Tsikani (mukakhale padziko
Lapansi) pakati panu pali chidani.
Ndipo (tsopano) pokhala panu ndi
pa Dziko lapansi, ndipo mukapeza
Chisangalalo pamenepo Chanthawi
yopimidwa."
37. Ndipo Adam adalandira
mawu kuchokera kwa Mbuye
wake, (napempha chikhululuko
Cha Allah kupyolera m'mawuwo),
Ndipo (Mbuye wake) adavomera
kulapa Kwake. Ndithudi, Iyeyo
Ngolandira Kwambiri kulapa,
Wachisoni.
38. Tidati : "Tsikani
m'menemo nonsenu; Ngati
chitakufikani chiongoko
Chochokera kwa Ine, ndipo amene
adzatsate Chiongoko changacho,
paiwo sipadzakhala Mantha.
Ndiponso iwo sadzadandaula.
39. "Koma amene
sanakhulupirire Anatsutsa mawu
athu, Iwowo ndiwo anthu a kumoto.
M'menemo akakhalamo muyaya."
«£SS»'
Surat 2. AI-Baqarah Juzu 1
13
1 *>i
t OjiJ* djj-*
40. E inu ana a Israyeli!
Kumbukirani Chisomo changa
chomwe ndidakudalitsani Nacho,
ndipo kwaniritsani pangano lanu
nanenso Ndikukwanitsirani
pangano langa Pa inu. Ndipo ine
ndekha ndiopeni.
41. Ndipo khulupirirani zimene
ndazivumbulutsa, Zomwe
zikuchitira umboni zimene muli
nazo, Ndipo musakhale oyamba
kuzikana; ndipo Musagulitse
mawu anga ndi (zinthu za) Mtengo
wochepa. Ndipo Ine ndekha
ndiopeni.
42. Ndipo musasakanize
choona Ndi chonama; ndikubisa
Choona uku mukudziwa.
43. Ndipo pempherani swala
moyenera Ndikupereka chopereka
(Zakati), Ndipo weramani pamodzi
ndi owerama.
44. Kodi mukulamula anthu
kuchita zabwino Ndi kudziiwala
inu eni pomwe inu Mukuwerenga
Buku? Kodi simuzindikira?
45. Ndipo dzithandizeni (pa
zinthu zanu) Popilira ndi
popemphera swala. Ndithudi,
swalayo ndiyolemera Kupatula kwa
odzichepetsa.
46. Omwe akutsimikiza kuti
adzakumana ndi Mbuye wawo,
ndikuti adzabwerera kwa lye.
OJ\J\
" fill'"
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1
14
\ *>i
Y oyJi 5jj-»
47. E inu ana a Israyeli!
Kumbukirani Chisomo changa
chomwe ndidakudalitsani Nacho.
Ndithudi, Ine ndinakuchitirani
Zaufulu kuposa zolengedwa zonse.
48. Choncho opani tsiku
lomwe munthu Aliyense
sadzathandiza mnzake ndi
Chilichonse, ndipo
sikudzavomerezedwa Kwa iye
(munthuyo) chiombolo, ndiponso
Silidzalandiridwa dipo kwa iye;
ndipo iwo Sadzapulumutsidwa.
49. Ndipo (kumbukirani)
pamene Tidakupulumutsani kwa
anthu a Farawo, Omwe
adakuzunzani ndi chilango choipa;
Adali kuzinga (kupha) ana anu
achimuna Ndikuwasiya moyo
achikazi. Ndipo M'zimenezo
mudali mayeso aakulu Ochokera
kwa Mbuye wanu.
50. Ndipo (kumbukiraninso)
pamene Tidailekanitsa nyanja
chifukwa cha inu (Kuti muoloke
pa mchenga wouma), potero
Tidakupulumutsani ndi kuwamiza
anthu A Farawo (pamodzi ndi iye
mwini) uku Inu mukuona;
(chomwe chidali Chizizwa
choonekera).
51. (Kumbukiraninso) pamene
tidamulonjeza Musa (Mose)
masiku makumi anayi (kuti
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1 15 \ ^jJb-t
t S^aJi 3jj-*»
Tidzampatsa buku la Chipangano
Chakale patapita Masiku makumi
anayi pambuyo Pakupulumuka
kwanu ndikuonongeka kwa
Farawo); kenako inu
mudapembedza Mwana wa
ng'ombe pambuyo pake, (iye
Kulibe, atapita ku chipangano cha
Mbuye wake). Ndipo inu muli
ochita zoipa.
52. Kenako
tidakukhululukirani pambuyo
Pazimenezo, kuti muthokoze
(mtendere Wa Mulungu).
53. Ndipo (kumbukiraninso)
pamene Musa (Mose) tidampatsa
buku Lolekanitsa choonadi ndi
chonama kuti Inu muongoke
(polilingalira ndi Kutsatira
malamulo ake)."
54. Ndipo (kumbukiraninso)
pamene Musa (Mose) Adanena
kwa anthu ake kuti "E inu anthu
Anga! Ndithudi, inu mwadzichitira
nokha zoipa Pompembedza mwana
wa ng'ombe. Choncho lapani kwa
Mlengi wanu, Ndipo phanani
nokha (amene ali Wabwino aphe
oipa). Kutero ndi bwino Kwa inu
pamaso pa Mlengi wanu."
Choncho wavomera kulapa kwanu.
Ndithudi, Iye Ngovomera kulapa
Mochuluka, Wachisoni.
55. Ndipo (kumbukiraninso
nkhani iyi) pamene Mudati: "E iwe
q&M#6
&*$&&$£&&
a <:?'<&
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1 16 > tjA-i
T SyLJt Ojj~>
Musa (Mose)!;
Sitingakukhulupirire iwe mpaka
Timuone Mulungu
masomphenya." Ndipo Nkokomo
wa moto udakugwirani Uku inu
mukuona.
56. Kenako tidakuukitsani
kuimfa Pambuyo pakufa kwanu,
Kuti muyamike.
57. Ndipo tidakuphimbani ndi
mthunzi Wamitambo (pamene
mudali kuoloka Chipululu cha
mchenga), ndipo Tidakutsitsirani
mana ndi salwa, Ndi kukuuzani:
"Idyani zinthu zabwino Izi zimene
takupatsani." Komatu Sadatichitire
Ife choipa koma adali Kudzichitira
okha zoipa.
58. Ndipo (kumbukiraninso
nkhani iyi) pamene Tidati:
"Lowani m'mudzi uwu, ndikudya
M'menemo motakasuka paliponse
pamene Mwafuna; ndipo lowerani
pachipata Chake uku mutawerama
(kusonyeza Kuthokoza Mulungu)
ndipo nenani "E Mbuye wathu!
Tikhululukireni Machimo athu".
"Tikukhululukirani Machimo anu
ndikuwaonjezera (mphoto
Yaikulu) ochita zabwino."
59. Koma anthu oipa adasintha
(lamulo la Mulungu, nanena)
mawu ena osati Amene
adawuzidwa; (choncho adalowa
\*'*9 "Mi\\ 9 ~ 9\<*\*<' J*'*.*"
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1
17
1 *jk-\
Y Sjiil 3jj-*»
Uku akukhwekhwerera ndi matako
awo). Tero Anthu oipawo
tidawatsitsira mliri Wochokera
kumwamba, chifukwa
Chakutuluka kwawo m'chilamulo
cha Mulungu.
60. Ndipo (kumbukiraninso
nkhani iyi) Pamene Musa (Mose)
adapemphera anthu Ake madzi
kwa Mulungu (atagwidwa ndi
Ludzu loopsa m'chipululu), tidati:
"Menya mwala ndi ndodo
Yakoyo." (Atamenya), anatulukadi
M'menemo akasupe khumi ndi
awiri. Potero fuko lililonse
lidadziwa malo Awo omwera. (Izi
zidachitika kuti Asakangane).
Choncho idyani, ndiponso Imwani
muriziki (zopatsa) la Mulungu
(Popanda inu kulivutikira), ndipo
musasimbwe Padziko uku
mukuononga.
61. Ndipo (kumbukiraninso
nkhani iyi) Pamene mudati: "E!
iwe Musa (Mose)! Sitingathe
kupirira ndi chakudya Chamtundu
umodzi (chomwe ndi mana ndi
Salwa); choncho tipemphere kwa
Mbuye Wako kuti atitulutsire
(atipatse) ife Zimene nthaka
imameretsa, monga Masamba,
nkhaka, adyo, nyemba Za mtundu
wa chana ndi anyezi." lye adati:
"Kodi mukufuna kusinthitsa
Chonyozeka (choipa) ndi
chabwino? Pitani m'midzi, ndipo
6£*3&fBtfc&S»&
®<
~^S9 9 J 9S9 .
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1 18 \ *jk-\
Y oyJl 5jj-**
kumeneko mukapeza Zimene
mwapemphazi" potero
adapatsidwa Kunyozeka ndi
kusauka; nabwerera ndi Mkwiyo
wa Mulungu. Zimenezo
n'chifukwa Chakuti iwo sadali
okhulupirira Zisonyezo za
Mulungu, ndikuti adali kupha
Aneneri a Mulungu popanda
chifukwa. Zidali tero chifukwa cha
kunyoza kwawo, Ndipo adali
olumpha malire.
62. Ndithu, amene akhulupirira
(Aneneri akale), Ndi Ayuda, ndi
aKhirisitu ndi Sabayi; Aliyense
waiwo amene akhulupirire
Mulungu (Tsopano, monga
momwe akunenera Mneneri
Muhammadi {SAW})
nakhulupiriranso za tsiku
Lomaliza, uku akuchita ntchito
zabwino, Akalandira mphoto yawo
kwa Mbuye wawo. Paiwo
sipadzakhala mantha, ndiponso
Sadzadandaula.
63. Ndipo (kumbukiraninso
nkhani iyi, inu Ayuda) pamene
tidalandira chipangano Chanu (kuti
mudzagwiritsa ntchito Zomwe zili
m'buku la Taurat), ndipo
Tidakweza pamwamba panu phiri
(La Sinai; tidati kwa inu:)
"Gwirani Mwamphamvu chimene
takupatsani, ndipo Kumbukirani
zili m'menemo (pozigwiritsa
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1
19
\ *>»
T oyaJl 5jj-»>
Ntchito. Ndiponso musazinyozere)
kuti Mukhale oopa Mulungu."
64. Komapambuyo
pazimenezo mudatembenuka
Ndikunyoza. Pakadapanda ufulu
wa Mulungu ndi chifundo chake
pa inu, Mukadakhala mwa otayika
(oonongeka Padziko lapansi).
65. Ndithudi mudawadziwa
anthu amene mwainu Adapyola
malire pakuswa Kupatulika kwa
Tsiku la sabata (m'mene
tidawalangira Chifukwa chosodza
nsomba patsiku Loletsedwa).
Ndipo tidati kwa iwo: "Khalani
anyani onyozeka."
66. Ndipo tidakuchita kukhala
anyaniko, Chilango chochenjeza
amene Adalipo pa nthawiyo ndi
akudza Pambuyo pawo, ndiponso
Phunziro kwa oopa Mulungu.
67. (Kumbukiraninso nkhani
iyi, inu Ayuda) Pamene Musa
adauza anthu ake: "Ndithudi,
Mulungu akukulamulani kuti
Muzinge ng'ombe." Iwo adati:
"Kodi Ukutichitira zachibwana?"
lye Adati: "(Sichoncho).
NdikudzitchinjirizaNdi Mulungu
kukhala mwa anthu aumbuli."
68. Iwo adati: "Choncho
tipemphere kwa Mbuye wako kuti
atifotokozere bwino Mtundu wa
ng'ombewo." lye adati "Ndithudi
>&c&&$M>&t»i®z
WMifKi
Siirat 2. Al-Baqarah Juzu 1 20 M *j^ y
t IjLlS Ijj^i
lye akunena kuti ng'ombeyo
simkota kapena Mthanthi, koma
yapakatikati pa zimenezi. Tero
chitani zimene mukulamulidwa."
69. Iwo adatinso: "Tipemphere
kwa Mbuye Wako kuti
atilongosolere maonekedwe Ake a
ng'ombeyo." (Musa) adati: "lye
Akuti ng'ombeyo ikhale yachikasu
Kwambiri, yowakondweretsa
oiwona."
70. Iwo adatinso: "Tipemphere
kwa Mbuye Wako kuti
atilongosolere mmene Khalidwe
lake lilili. Ndithudi, Ng'ombe
zimene wafotokozazo n'zofanana
kwa ife. Ndipo ndithudi, Mulungu
akafuna Tikhala oongoka."
71. Adati: "Ndithudi lye akuti,
imeneyo ndi n'gombe
Yosaigwiritsa ntchito yolima
m'nthaka, Ndiponso yosathirira
mbewu; yabwinobwino Yopanda
banga." Iwo adati: "Tsopano
Wabweretsa (mawu a) choonadi."
Choncho Adaizinga, koma
padatsala pang'ono kuti Asachite
(lamulolo).
72. Ndipo (kumbukiraninso
nkhani iyi) pamene Mudapha
munthu, kenako mudakangana ndi
Kukankhirana chifukwa cha
(munthuyo, ena Ankati uje ndiye
wapha. Pomwe ena ankati koma
9 &jj$"*'' 6 M-**
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1
21
S *>l
X 5^aJ| 5jj-j
Uje ndiye wapha). Ndipo Mulungu
atulutsira Poyera zimene mudali
kubisa.
73. Choncho tidati:
"Kwapulani thupi la Wakufayo ndi
gawo la nyamayo. (Potero auka
ndikunena za amene adamupha)."
Momwemo Mulungu adzawaukitsa
akufa (M'manda monga
adamuukitsira wakufayo pamaso
Panu), ndipo akukusonyezani
zizindikiro Zake kuti mukhale ndi
nzeru.
74. Koma mitima yanu idauma
pambuyo Pazimenezo; (ikhala
gwa!), ngati Mwala kapena
kuposerapo. Ndithudi Pali miyala
ina yomwe Mitsinje ikutuluka
mkati mwake; Ndipo pali ina
imene imang'ambika Nkutuluka
madzi mkati mwake; ndipo Pali
ina imene imagwa chifukwa Cha
kuopa Mulungu. (Koma inu Ayuda
Simulalikika ngakhale mpang'ono
Pom we). Ndipo Mulungu sali
Wonyalanyaza zimene mukuchita.
75. Kodi (inu Asilamu)
mukuyembekezera Kuti
angakukhulupirireni (Ayudawo)
Pomwe ena a iwo ankamvera
mawu A Mulungu, kenako
nkuwasintha Pambuyo
powazindikira bwinobwino,Uku
akudziwa?
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1
22
\ *>»
T SyUl Sjj-**
76. Ndipo akakumana ndi
amene Akhulupirira, amanena:
Takhulupirira (kuti uyu,
Muhammadi {SAW}Ndi mneneri
woona, ndipo watchulidwa
M'Mabuku athu)." Koma akakhala
Kwa okha kuseli, amati:
"Mukuwauza Iwo (Asilamu)
zimene Mulungu
Anakufotokozerani (M'buku la
Taurat) kuti Adzakhale ndi mtsutso
pa inu kwa Mbuye wanu? Kodi
mulibe nzeru?
77. "Kodi sadziwa kuti
Mulungu Akudziwa zomwe
akubisa ndi Zomwe akuonetsera
poyera? (Kwa Mulungu palibe
chobisika).
78. Ndipo mwa iwo
(Ayudawo) zilipo mbuli
Zosadziwa kuwerenga buku (la
Mulungu), Koma ziyembekezero
Zabodza basi, ndipo iwo alibe
china Koma zakungoganizira basi.
79. Chilango cha ukali
chidzatsimikizika Pa amene
akulemba buku ndi manja awo,
Kenako nanena: "Hi lachokera kwa
Mulungu," (akunena bodzalo) kuti
apeze Zinthu za mtengo wochepa
(za m'dziko Lapansi):
Kuonongeka kuli pa iwo Chifukwa
chazomwe manja awo alemba,
Ndipo kuonongeka n'kwawo
Chifukwa chazomwe adapeza.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1 23 ^ *jk*
t S^aJI 5jj-j
80. Ndipo akunena:
"Sudzatikhudza moto Kupatula
masiku owerengeka basi."Auze:
"Kodi mudapangana naye
Mulungu, kuti potero sadzaswa
lonjezo Lake, kapena
mukungomunenera Mulungu
Zimene simukuzidziwa?"
81. Sichoncho! Komaamene
wachita Choipa, ndi
kuzunguliridwa Ndi machimo ake,
otero ndi Anthu a kumoto.
M'menemoAdzakhala muyaya.
82. Ndipo amene akhulupirira
nachita zabwino, Iwowo ndiwo
anthu akumunda wa mtendere.
M'menemo adzakhala muyaya.
83. Ndipo (akumbutse nkhani
iyinso) pamene Tidalandira
pangano lamphamvu la ana A
Israyeli kuti: Musapembedze
aliyense Koma Mulungu; ndipo
muwachitire zabwino Makolo anu
ndi achibale anu, ndi amasiye,Ndi
masikini (osowedwa); ndipo
nenani Kwa anthu mwaubwino;
ndipo pempherani Swala moyenera
ndi kupereka Zakati Kenako
mudatembenuka monyozera
kupatula Ochepa mwainu, ndipo
inu ndinu onyozera.
84. Ndipo kumbukirani
pamene tidalandira pangano Lanu
kuti simukhetsa mwazi wanu,
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1 24 ^ *j^
t djiJi djj-*»
kutinso Simudzawatulutsa anthu
anu m'midzi yanu, Ndipo inu
munavomereza zimenezi, ndipo,
Inu mukuikira umboni zimenezi
(Koma simudatsate malamulowo).
85. Tsono inu nomwe ndi
amene mukuphana Ndikuwatulutsa
ena a inu m'nyumba
zawo;Mukuthandiza adani anu
powachitira (Abale anu masautso)
mwauchimo ndi Molumpha malire.
Koma akakudzerani Akaidi,
mukuwaombola, pomwe
nkoletsedwa Kwainu kuwatulutsa.
Kodi mukukhulupirira Mbali ina
ya buku, mbali ina nkuikana?
Choncho palibe mphoto kwa
ochita izi Mwainu koma kuyaluka
pamoyo wa padziko Lapansi;
ndipo tsiku la chiweruzo
Adzalowetsedwa ku chilango
chaukali. Ndipo Mulungu sali
wonyalanyaza zimene mukuchita.
86. Iwowo ndi amene
asinthanitsa Moyo wa tsiku
lomaliza ndi Moyo wadziko
lapansi Choncho
sadzawachepetsera chilango,
Ndiponso sadzapulumutsidwa.
87. Ndithudi Musa tidampatsa
buku (la Taurat) Ndipo tidatsatiza
pambuyo pake atumiki (Ena).
Ndipo Yesu mwana wa Mariya
Tidampatsa zizizwa zoonekera, ndi
s 9} ' lift*?' ?2- 9 '2{
"9"9i S* t'9'\' ■ \S&\[ ^ 9 "
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1 25 > *&
t djAJl $JJ~»
Kumulimbikitsa ndi Mzimu
Woyera (Gabrieli). Nthawi
iliyonse Akakudzerani mtumiki
ndi chomwe Mitima yanu
siikonda, mumadzikweza. Ena
mudawatsutsa ndipo ena
mudawapha.
88. (Iwo) adati: "Mitima yathu
yakutidwa, (Potero tikulephera
kumvetsa ulaliki Wako, iwe,
Muhammadi {SAW}. Iwo
ngabodza Pazimene akunenazi).
Koma Mulungu Wawatemberera
chifukwa cha Kusakhulupirira
kwawo. Tero n'zochepa Zimene
akuzikhulupirira.
89. Ndipo pamene buku
lidawadzera (m'nyengo Ya
mtumiki Muhammadi {SAW})
lochokera kwa Mulungu, loikira
umboni zomwe zili Pamodzi ndi
iwo (adalikana) pomwe Kale
(lisadadze bukulo) adali kupempha
Chithandizo kupyolera kwa
mtumiki Wolonjezedwa
chogonjetsera amene
Sadakhulupirire. Koma pamene
Chidawadzera chimene
adachidziwa, (Qur'an)
Adachikana. Choncho
matemberero A Mulungu ali pa
osakhulupirira.
90. N'choipa zedi chimene
agula Pogulitsa chisangalalo cha
tsiku Lomaliza cha mitima yawo,
>&£&&>£&%$$%
®v£&r**' iiA
*je
^j\^^^i^^s^^^
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1
26
> *jk-\
T djiJi djj^
ndi pokana Pawo zimene Mulungu
adavumbulutsa, Chifukwa cha
njiru basi kuti Mulungu Watsitsira
chifundo chake amene wamfuna
Mwa akapolo ake (amene sali
m'Yuda). Potero adabwerera Ndi
mkwiyo wa Mulungu kuonjezera
Pamkwiyo wakale. Ndipo
osakhulupirira Adzakhala ndi
chilango chosambula.
91. Ndipo akauzidwa (Ayuda):
"Khulupirirani zimene Mulungu
wavumbulutsa (Kwa mtumiki
Muhammadi {SAW})" amanena:
"Tikukhulupirira zimene
zidavumbulitsidwa Kwaife."
Ndipo amazikana zomwe Sizili
zimenezo ngakhale icho chili
Choona, chomwe chikuikira
umboni kuona Kwa zomwe ali
nazo pamodzi. Nena: "Nanga
bwanji mudapha aneneri a
Mulungu Kalelo ngati muli
okhulupiriradi?"
92. Ndipo adakudzerani Musa
ndi Zisonyezo zotsimikizika, koma
pambuyo Pake mudapembedza
mwana wa ng'ombe, Ndipo potero
mudali anthu Ochita zoipa
kwabasi.
93. Ndipo (kumbukirani nkhani
iyi, inu Ana a Israyeli) pamene
tidalandira Kwainu pangano
lamphamvu, ndipo
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1 27 > *&
t 5yJl 5jj-»»
Tidakukwezerani phiri pamwamba
panu (Uku tikuti): "Gwiritsani
mwamphamvu (Malamulo) amene
takupatsani, ndipo Mverani." (I wo)
adati: "tamva (mawu anu), Koma
tikunyoza (tikukana lamulo lanu)."
Ndipo adamwetsedwa m'mitima
mwawo (Kukonda kupembedza)
mwana wang'ombe Chifukwa cha
kusakhulupirira kwawo. Nena:
"N'choipa zedi chimene
chikhulupiriro Chanu
chikukulamulirani ngati inu Mulidi
okhulupirira."
94. Auze (Ayudawo): "Ngati
nyumba Yomaliza kwa Mulungu
njanu nokha, osati Anthu ena
(monga momwe mukunenera),
Ilakalakeni imfa ngati mukunenadi
zoona."
95. Koma sadzailakalaka
(imfa) ngakhale pang'ono,
Chifukwa cha zomwe manja awo
adatsogoza (Chifukwa cha
machimo adadzichitira). Ndipo
Mulungu akudziwa Bwino za
anthu oipa.
96. Ndipo muapeza (Ayuda)
kuti Ngokondetsetsa kukhala ndi
moyo Wautali kuposa anthu ena,
Kuposanso anthu amene
akuphatikiza Mulungu (ndi
mafano). Aliyense Waiwo
amafuna apatsidwe moyo
£*>*.&>
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1
28
\ *>»
t djiJl djj-*
wokwana Zaka chikwi chimodzi.
Pomwe kupatsidwa Kwake moyo
wautali sikungamuike kutali ndi
Chilango. Ndipo Mulungu akuona
zonse Zimene akuchita.
97. Nena: "Amene akhale
mdani wa Gaburieli (Chifukwa
chobweretsa Chivumbulutso kwa
Muhammadi {SAW}, iyeyo ndi
mdani wa Mulungu). Ndithudi, iye
Waivumbulutsa Qur'an mumtima
mwako Mwachilolezo cha
Mulungu. (Sadachite
Mwachifuniro chake). (Qur'an) ndi
Imene ikutsimikizira zomwe zidali
Patsogolo pake, ndiponso ndi
chiongoko Ndi nkhani yabwino
kwa okhulupirira.
98. Amene ali mdani wa
Mulungu, ndi Angelo Ake, ndi
Atumiki ake, ndi Gaburieli ndi
Mikayeli (ndiye kuti akudzifunira
imfa). Ndithu, Mulungu ndi mdani
wa Osakhulupirira.
99. Ndithu, tidavumbulutsa
kwa iwe Zisonyezo zooneka.
Ndipo palibe wozikana Koma
okhawo opandukira chilamulo cha
Mulungu.
100. Kodi sizili tero kuti
panthawi iliyonse Akupangana
pangano lamphamvu, ena aiwo
Akulitaya? Koma ambiri aiwo
sakhulupirira.
b$&i
Ju^ 4t^\i J-*$ji Oi&Z*
G¥ 9 >*\ \
Siirat 2. Al-Baqarah Juzu 1 29 > *>'
t o^iJl 5jj~>
101. Ndipo pamene (Ayuda)
adawadzera mtumiki Wochokera
kwa Mulungu uku akuchitira
umboni chomwe iwo ali nacho,
gulu Lina mwa omwe adapatsidwa
buku Adataya buku la Mulungu
Kumbuyo kwa misana yawo ngati
Kuti sakulidziwa.
102. Adatsatira njira za afiti
zomwe a Satana adali
kuwafotokozera m'nthawi ya
ufumu wa Sulaiman. Ndipo
Sulaiman sadali mfiti, (sadasiye
kukhulupirira Mulungu), Koma
aSatana ndi amene
sadakhulupirire, naphunzitsa anthu
ufiti (umene adaudziwa kuyambira
kale); natsatiranso njira za ufiti
zimene zinatsitsidwa kwa Angelo
awiri Haruta ndi Maruta (ku midzi
ya) ku Babulo. Koma Angelo wo
sadaphunzitse aliyense
pokhapokha atamuuza kuti: "Ife
ndife mayeso (ofuna kuona
kugonjera kwanu malamulo a
Mulungu); Choncho musamkane
(Mulungu)." Komabe
ankaphunzira kwaiwo njira
zolekanitsira pakati pa munthu ndi
mkazi wake, (ndi zina zotero).
Ndipo sadavutitse aliyense ndi
zimenezo koma mwachilolezo cha
Mulungu. Ndipo akuphunzira
zomwe zingawavutitse pomwe
sizingawathandize. Ndithudi,
6 &&&&&&%>
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1
30
> *>i
T S^iJl Sj>*>
akudziwa kuti yemwe wausankha
(ufitiwo) sadzakhala ndi gawo
lililonse (la zinthu zabwino) tsiku
lomaliza. Ndithudi, nchoipitsitsa
chimene adzisankhira okha
akadakhala akudziwa.
103. Ndipo iwo
akadakhulupirira nadzitchinjiriza
(ku zoletsedwa), ndithudi, mphoto
yochokera kwa Mulungu
ikadakhala yabwino kwaiwo,
akadadziwa.
104. E inu amene
mwakhulupirira! musam'nenere
(M'neneri liwu lakuti) "raina"
(Ndicholinga chomunenera kuti
iye ndi mbutuma) Koma
mnenereni (liwu lakuti)
"utiyang'anire", ndipo mverani
Malamulo. Kwa osakhulupirira
kuli chilango chopweteka.
105. Amene sadakhulupirire
mwa anthu amabuku (Ayuda ndi
Akhirisitu) ndi omphatikiza
Mulungu (Arabu), safuna kuti
chabwino chilichonse chochokera
kwa Mbuye wanu chitsitsidwe
kwainu (Asilamu). Koma Mulungu
amamsankhira chifundo chake
amene wamfuna. Ndipo Mulungu
ndi mwini chifundo chochuluka.
106. Ay a (ndime) iliyonse
yomwe tikuifafaniza kapena
kuiiwalitsa (mumtima wako)
Tikubweretsa yabwino kuposa iyo,
(J*~«*d 46»J>^J &£?-
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1 31 S *jJfc-i
y djiS\ 5jj^»
Kapena yofanana nayo. Kodi
sukudziwa Kuti Mulungu
ngokhoza chinthu Chilichonse?
107. Kodi siudziwa kuti ufumu
wakumwamba ndi Pansi ngwa
Mulungu? Ndipo inu kupatula lye
Mulungu mulibe mtetezi ngakhale
Mthandizi.
108. Kodi mukufuna kumfunsa
mtumiki wanu (Inu Asilamu)
monga momwe Musa (Mose)
Adafunsidwira kale (mafunso
achipongwe)? Ndipo amene
angasinthitse chikhulupiriro ndi
Kusakhulupirira, ndithudi
wasokera njira Yolingana
(yopanda majiga).
109. Ambiri mwa amene
anapatsidwa mabuku Akufuna
kukubwezani (kukutembenuzani)
Kuti mukhale osakhulupirira
pambuyo pa Chikhulupiriro chanu
chifukwa chadumbo Lomwe lili
m'mitima mwawo (lomwe
Lawapeza) pambuyo powaonekera
choonadi Poyera. Choncho
akhululukireni ndi Kuwasiya
kufikira Mulungu adzabweretse
lamulo Lake; ndithudi Mulungu
ngokhoza chilichonse.
110. Ndipo pempherani swala
moyenera Ndiponso perekani
Zakati. Ndipo chilichonse
Chabwino chimene
<J 9 c
qj&Sjp
Siirat 2. Al-Baqarah Juzu 1 32 > *>■!
X SjiJi 3jj--
mukudzitsogozera Mukachipeza
kwa Mulungu. Ndithudi, Mulungu
Akuona zonse zimene mukuchita.
111. Eti akunena: "palibe amene
adzalowe ku Munda wa mtendere
koma amene ali Myuda Kapena
Mkhirisitu." Zimenezo nzofuna
Zawo chabe. Nena: "Bweretsani
umboni Wanu ngati mukunena
zoona."
112. Ayi, koma amene nkhope
yake yagonjera kwa Mulungu uku
akuchita zabwino (kwa anthu
Anzawo) iye ndi amene adzapeza
mphoto yake Kwa Mbuye wake.
Ndipo paiwo sipadzakhala Mantha,
ndiponso iwo sadzadandaula.
113. Ndipo Ayuda akumanena:
"Akhrisitu alibe chilichonse
(chotsamira pachipembedzo
chawo);" naonso Akhrisitu
akumanena: "Ayuda alibe
chilichonse (chotsamira
pachipembedzo chawo)," pomwe
onsewa akuwerenga Buku
(lomwe adawavumbulutsira
popanda kutsatira zili m'bukulo).
Mofanana ndi zoyankhula zawo,
momwemonso akunena amene sali
odziwa (Arabu opembedza
mafano) monga zonena za Ayuda.
Mulungu adzaweruza pakati pawo
tsiku la chimaliziro pazomwe adali
kusiyana.
*£&' > fit % ><&'**«'<> L 99 'i
Siirat 2. AI-Baqarah Juzu 1 33 > *jJfc-i
t O^flJi OjJ-K
114. Kodi alipo woipitsitsa
woposa amene akutsekereza (anthu
kulowa) m'misikiti ya Mulungu
kuti lisatchulidwe m'menemo
dzina lake nalimbika kuiononga
(misikitiyo)? - Kotero kuti sikunali
koyenera kwa iwo kulowa
mmenemo koma mwa mantha.
Kuyaluka kwapadziko lapansi
nkwawo ndipo tsiku lomaliza iwo
adzapeza chilango chachikulu.
115. Ndipo kuvuma ndi
kuzambwe nkwa Mulungu; ndipo
pamalo paliponse pamene
mwatembenukira, (pomwe
Mulungu wakulamulirani kuti
mutembenukire), pamenepo
mupezapo chiyanjo cha Mulungu.
Ndithudi Mulungu ngokwanira
ponseponse, wodziwa chilichonse.
116. Ndipo (osakhulupirira)
akumanena: "Mulungu
wadzipangira mwana." (Mulungu)
wapatukana ndi zimenezo. Koma
(zolengedwa) zonse za kumwamba
ndi pansi nzake. Zonse
zikumumvera lye.
117. (lye ndi) Mlengi wathambo
ndi nthaka popanda chofanizira.
Ndipo akafuna chinthu kuti
chichitike amangoti: "chitika,"
ndipo chimachitikadi.
118. Ndipo aja osadziwa
akunena: "Bwanji Mulungu
M^*^$$2t&
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1 34 \ ^\
Y $jiJ\ 3jj--
osatilankhula ife? Kapena
kutibweretsera chizindikiro
(chizizwa)?" Mofanana ndi
zoyankhula zawozo adanenanso
amene adalipo kale. Mitima yawo
yalingana. Ndithu, Ife tazifotokoza
zizindikiro momveka kwa anthu
otsimikiza (m'chikhulupiriro).
119. Ndithudi, Ife takutumiza
(iwe Mtumiki {SAW}) Ndi
choonadi kuti ukhale wouza
nkhani zabwino, ndi wochenjeza.
Ndipo siudzafunsidwa za anthu
aku moto.
120. Ndipo Ayuda ndi Akhrisitu
sangakondwere nawe pokhapokha
utatsatira zipembedzo zawo. Nena:
"Ndithudi, chiongoko cha
Mulungu ndichomwe chili
chiongoko chenicheni." Ngati
utsata zilakolako zawo pambuyo
pazomwe zakudzera, monga
kuzindikira (kwenikweni),
sudzapeza mtetezi aliyense
ngakhale mthandizi kwa Mulungu.
121. Anthu omwe tidawapatsa
Buku naliwelenga; kuwerenga
koyenera (kopanda kusintha mawu
ake ndi matanthauzo ake), iwo ndi
amene akulikhulupirira (Bukuli la
Qur'an). Koma amene angalikane
iwowa ndi omwe ali oonongeka.
122. E inu ana a Israyeli! :
kumbukirani chisomo changa
&tyo^&&&k
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1 35 > ^
t 5jaJ' $jj-»
chomwe ndidakudalitsani nacho.
Ndithudi, ndidakuchitirani
zabwino kuposa zolengedwa zonse
(panthawi imeneyo).
123. Ndipo opani tsiku lomwe
munthu aliyense sadzathandiza
munthu mnzake ndi chilichonse,
ndipo dipo silidzalandiridwa,
ndipo kuombola kwa owombola
sikudzamthandiza, ndiponso iwo
sadzapulumutsidwa.
124. Ndipo kumbukirani
pamene Mbuye wa Ibrahim (Allah)
adamuyesa iye mayeso ndi
malamulo ambiri; ndipo iye
adakwaniritsa. Adamuuza:
"Ndithudi, Ine ndichita iwe
kukhala mtsogoleri wa anthu."
(Ibrahim adayankha kuti): "Kodi
ndi ana anga omwe?" Adati:
"(Inde; koma) lonjezo langa
silingawafike Ochita zoipa."
125. Ndipo (kumbukiraninso
nkhani iyi) pamene tidapanga
Nyumba (ya Al-Kaaba) kuti
pakhale pamalo pobwelerapo
anthu (poyendera anthu)
ndikukhalanso malo achitetezo.
Ndikuti pachiteni kukhala
popemphelera Swala pamalo
pomwe Ibrahim adali kuimilira
(pomamga nyumbayo). Ndipo
tidal amula Ibrahim ndi Ismail kuti:
"Iyeretseni nyumba yanga
®<*$\&&&$s$&
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1
36
\ >>»
T 5jiJl 5jj-»»
chifukwa cha oizungulira (pochita
tawaf) ndi amene akuchita
mbindikiro, ndi chifukwa cha
Amene akuwerama ndi kulambira
(kuswali Mmememo).
126. Ndipo (kumbukirani nkhani
iyi) Pamene Ibrahim adanena: "O!
Mbuye wanga! : Uchiteni mzinda
uwu (wa Makka) kukhala wa
Chitetezo, ndipo zipatseni nzika
zamunzindawu Zipatso amene
akukhulupirira Mulungu Ndi tsiku
lomaliza mwaiwo. Mulungu adati:
"Nayenso wosakhulupirira
ndinkondweretsa Pang'ono;
kenako ndidzamkankhira ku
chilango Cha mo to. Taonani
kunyansa malo obwerera.
127. Ndipo (kumbukiraninso)
pamene Ibrahim ndi Ismaila
ankakhazikitsa maziko a nyumba
(Uku akupempha kwa Mulungu):
"O! Mbuye Wathu! Tilandireni
(ntchito yathuyi), Ndithudi, Inu
ndinu Akumva; Odziwa."
128. "O! Mbuye wathu! tichiteni
kukhala ogonjera Inu, pamodzinso
ndi ana athu muwachite kukhala
Fuko logonjera Inu. Ndipo
tidziwitseni (njira) Za
mapemphero athu; ndipo
tikhululukireni, Ndithudi, Inu
ndinu wolandira kulapa
Mochuluka; Wachisoni."
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1 37 \ *jJH
t OjaJi 5jj-»
129. "O! Mbuyewathu!
Atumizireni mtumiki wochokera
mwaiwo, kuti awawerengere ay a
(ndime) zanu ndikuwaphunzitsa
Buku (lanu) ndi nzeru ndikuti
awayeretse. Inu ndinu Amphamvu
zoposa, Anzeru zakuya."
130. Kodi ndani wonyoza
chipembedzo cha Ibrahim osati
yemwe mtima wake uli wopusa?
Ndithudi, tidamsankha (Ibrahim)
padziko lapansi; ndipo iye Tsiku
lomaliza adzakhala m'modzi wa
anthu abwino."
131. (Kumbukiraninso) pamene
Mbuye wake adamuuza kuti:
"Gonjera." (Iye) adati:
"Ndagonjera kwa Mbuye
wazolengedwa zonse."
132. Ndipo Ibrahim
adalangizanso ana ake zazimenezi,
chonchonso Yakubu
(adalangizanso ana ake kuti): "E
inu ana anga! Ndithudi, Mulungu
wakusankhirani chipembedzo;
choncho musafe pokhapokha muli
ogonjera Iye."
133. Kodi inu (Ayuda ndi
Akhrisitu) mudalipo pamene
Yakubu idamdzera imfa. pamene
adati kwa ana ake: "Kodi pambuyo
panga mudzapembedza yani?" Iwo
adayankha nati: "Tidzapembedza
Mulungu wako, Mulungu
','\ h g 91.9' * j, 9 *'? JS *if> \"
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1 38 1 *j*-i
t oyLJl 5jj-j
wamakolo ako, Ibrahim, Isimail
ndi Isihaka; Mulungu m'modzi
basi. Ndipo ife tikugonjera lye.
134. Umenewo ndi mbadwo wa
anthu umene udamka Kale.
Udzapeza zimene udachita, ndipo
inunso Mudzapeza zimene
mudachita. Ndipo inu
simudzafunsidwa zimene iwo
ankachita.
135. (Iwo Ayuda) adati (kwa
Asilamu): "Khalani Ayuda (ndipo
mukhala oongoka)." (Naonso
Akhrisitu adati): "Khalani
Akhrisitu (ndipo mukhala
oongoka)." Nena: "Koma
(tikutsata) chipembedzo cha
Ibrahim yemwe adaleka
zipembedzo zopotoka, ndipo sadali
mwa ophatikiza Mulungu ndi
mafano."
136. Nenani (inu Asilamu
kuwauza Ayuda ndi Akhrisitu):
"Takhulupirira Mulungu ndi
zimene adavumbulutsa kwa ife,
ndi zimene zidavumbulutsidwa
kwa Ibrahim, Isimail, Isihaka,
Yakubu ndi zidzukulu (zake) ndi
zimene adapatsidwa Musa, Yesu,
ndiponso zimene adapatsidwa
Aneneri (ena) kuchokera kwa
Mbuye wawo. Sitilekanitsa pakati
pammodzi wa iwo (koma onse
tikuwakhulupirira). Ndipo ife
tikugonjera lye."
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 1
39
S *j*-i
Y 9jaA\ «jj->
137. Ngati akhulupirira (Ayuda
ndi Akhrisitu) monga m'mene
mwakhulupirira, ndiye kuti
awongoka. Koma ngati
akutembenuka (posakhulupirira)
ndiye kuti iwo ali m'kukangana.
Choncho Mulungu akuteteza
kuzoipa zawo, ndipo lye
Ngwakumva; Wodziwa.
138. (Tsatirani) chiongoko cha
Mulungu (Chisilamu). Kodi ndi
ndani amene ali ndi chiongoko
Chabwino kuposa Mulungu?
Ndipo ife, lye yekha
timupembedza.
139. Nena (iwe Muhammad
{SAW}kwa Ayuda ndi Akhrisitu):
"Ha! Mukutsutsana nafe za
Mulungu (ponena kuti bwanji
wapereka uneneri kumbali yaife),
pomwe lye ndi Mbuye wathu
ndiponso Mbuye wanu? (Pamene
mudali olungama adakupatsani
uneneri. Ndipo pamene mudakhota
adakulandani natipatsa ife). Ife tili
ndi zochita zathu; inunso muli ndi
zochita zanu, ndipo ife
tikudzipereka kwathunthu kwa lye
(Mulungu).
140. Kodi mukunena (Ayuda)
kuti Ibrahim, Ismael Ishag, Yaqub
ndi zizukulu Anali Ayuda kapena
Akhrisitu? Nena: "Kodi inu ndi
odziwa kwambiri Kapena
Mulungu?" Kodi ndiyani oipitsitsa
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
40
t *>i
t 0jaJ\ 5jj-*
kwambiri kwa lye Koposa yemwe
wabisa umboni Ochokera kwa
Mulungu! Komatu Mulungu sali
wonyalanyaza Pazimene
mukuchita.
141. Iwo ndi mbadwo wa anthu
umene Udanka kale (palibe phindu
Kuwanyadira iwo) udapeza zimene
Udachita, ndipo inunso mudzapeza
Zimene mudachita. Ndipo inu
Simudzafunsidwa pazimene Iwo
ankachita.
142. Posachedwapa mbutuma za
anthu Zikhala zikunena: "Nchiyani
chimene Chawatembenula ku
chibula chawo Chomwe akhala
akulunjika nkhope zawo." Nena:
"Kuvuma ndi kuzambwe Ndi kwa
Mulungu amamuongolera Amene
wamfuna kunjira yolunjika."
143. Choncho takusankhani
(inu asilamu) kukhala mpingo
wabwino (wapakatikati) Kuti
mukhale mboni pa anthu ndi kuti
Mtumiki akhale mboni painu.
Ndipo chibula (Choyang'ana mbali
ya ku Yerusalemu) chomwe udali
nacho sitidachichite koma Kuti
timdziwitse (adziwike kwa anthu)
Amene akutsata mtumiki, ndi
yemwe Akutembenukira
m'mbuyo. Ndipo ndithudi, Chidali
chinthu chovuta kupatula kwa
omwe Mulungu wawaongola.
Ndipo nkosayenera Kwa Mulungu
©<^t£^>u;
t * 9% ' 3 *
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
41
Y *>■»
Y dyJl djj-*.
kusokoneza Swala zanu Pakuti
Mulungu Ngoleza kwabasi kwa
Anthu. Ngwachifundo chambiri. 1
144. Ndithudi, taona
kutembenuzatembenuza Kwa
nkhope yako (kuyang'ana)
kumwamba. Choncho
tikutembenuzira ku chibula
chimene Ukuchifuna. Tero
tembenuzira nkhope yako kumbali
ya msikiti woyera (Al-kaaba).
Ndipo paliponse pamene mulipo
Yang'anitsani nkhope zanu
kumene Kuli (msikitiwo). Ndithudi
amene Adapatsidwa Buku
akudziwitsitsa kuti chimenecho
nchoonadi chochokera Kwa
Mbuye wawo. Ndipo Mulungu
Siwonyalanyaza zimene akuchita.
(Koma Chilichonse
chikulembedwa m'kaundula).
145. Ndipo awo adapatsidwa
Buku ngakhale Utabwera ndi
chisonyezo cha mtundu Uliwonse
satsata chibula chako,
1 Apa akutanthauza kuti pamene takutsogolerani ku njira yolunjika, takulolani
inu ampingo wa Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale naye) kukhala
anthu olungama, kulungama kosapyola nako muyeso ndiponso kopanda
kuchepetsa chinthu chilichonse chazauzimu, ndi chamoyo wapadziko lino
lapansi. Mtundu wa Chisilamu ngwapakatikati mzokhulupilira zake zonse.
Umalimbikira kugwira ntchito ya zinthu za mdziko ndiponso ya zinthu
zauzimu mwakhama, chilichonse mwazimenezi amachilimbikira mosapyoza
muyeso. Limeneli ndilo tanthauzo la "mtundu wapakatikati." Chisilamu
sichiiekerera munthu mmodzi kuti apondereze anthu ambirimbiri; ndiponso
sichilekerera anthu ambiri kusalabadira za munthu mmodzi. Zimenezi
nchifukwa chakuti inuyo mukhale mboni pa anthu pano padziko lapansi,
ndikutinso mudzakhale mboni paiwo patsiku la chiweruzo. Ndipo kuti Mneneri
(SAW) adzakhale mboni painu.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
42
t >>i
t d^AJi OjJ~»
Ngankhalenso iwe sutsata chibula
chawo. Ndipo ena a iwo sali
otsatira chibula cha Ena (Akhrisitu
satsata chibula cha Ayuda. Ndipo
Ayuda satsata cha Akhrisitu).
Ngati utsatira zofuna zawo,
pambuyo Pakuti kwakudzera
kudziwa ndiye kuti ukhala Mwa
ochita zoipa.
146. Aja amene tidawapatsa
Buku akumuzindikira (Mtumiki
Muhammad {SAW}) monga
mom we Amawazindikirira ana
awo. Koma ena mwa Iwo akubisa
choonadi uku akudziwa.
147. (Kuyang'ana ku Al-kaaba
popemphera Swala Ndicho)
Choonadi chomwe chachokera
kwa Mbuye wako; choncho
usakhale mmodzi Mwa openekera.
148. Ndipo mpingo uliwonse
udali ndi chibula (Mbali
yoyang'ana popemphera) chimene
Udali kuchilunjika. Choncho
pikisanani pochita Zabwino.
Paliponse pamene mukhala
Mulungu Adzakubweretsani
nonsenu pamodzi (patsiku la
Chimaliziro). Ndithudi, Mulungu
ngokhoza chinthu Chilichonse.
149. Ndipo paliponse pomwe
wapita tembenuzira Nkhope yako
kumbali ya Msikiti Woyera
(Panthawi yopemphera).
Chimenecho Nchoonadi
%*$s^M*0v>&x
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
43
t *>»
t S^aJI 5jj-*>
chochokera kwa Mbuye wako.
Ndipo Mulungu sali wonyalanyaza
zimene Mukuchita.
150. Paliponse pamene wapita
(iwe Mtumiki) Tembenuzira
nkhope yako kumbali Ya Msikiti
woyera. Ndipo paliponse Pamene
(inu Asilamu) Muli tembenuzirani
nkhope Zanu kumbali yake (Ya
Msikiti) kuti anthu asakhale Ndi
mtsutso pa inu, kupatula Amene
adzichitira zoipa mwa iwo. Tero
musawaope, koma Opani Ine,
ndipo ndikwaniritsa Chisomo
changa pa inu kuti muongoke.
151. Monganso tidamtumiza
mtumiki kwa inu Wochokera mwa
inu kuti akuwerengereni aya
(Ndime) zathu, ndikukuyeretsani
(kuuve Wopembedza mafano) ndi
kukuphunzitsani Buku ndi nzeru,
ndikukuphunzitsani Zimene
simunali kuzidziwa.
152. Choncho ndikumbukireni
(pondithokoza Pamtendere umene
ndakupatsaniwu.) Nanenso
ndikukumbukirani (pokulipirani
Mphoto yaikulu). Ndipo
ndiyamikeni; Musandikane.
153. E inu amene
mwakhulupirira! Dzithandizeni
(Pazinthu zanu) popirira, ndi
popemphera Swala. Ndithudi,
®$M$^%%>M
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
44
X tjk-\
t o^iJl Sjj-u
Mulungu ali pamodzi ndi opirira.
154. Ndipo musanene za amene
aphedwa pa Njira ya Mulungu kuti
"ngakufa." Iyayi Ngamoyo, koma
inu simuzindikira.
155. Ndipo tikuyesani ndi
chinthu choopsa (monga
Nkhondo), njala, kuchepa kwa
chuma, kutaika Kwa miyoyo ndi
kuonongeka kwa mbeu. Tero auze
nkhani yabwino opirira.
156. Omwe mavuto akawapeza
amati: "Ndithudi, Ife nga
Mulungu, ndipo kwa lye ndiko
Tidzabwerera."
157. Otero ndi amene ali ndi
madalitso ndi Chifundo
chochokera kwa Mbuye wawo.
Ndiponso iwo ndi amene ali
oongoka.
158. Ndithudi, Safaa ndi Marwa
(mapiri awiri Omwe pakati pake
pamachitika pemphero Loyenda
ndawala) ndi zizindikiro
Zolemekezera chipembedzo cha
Mulungu. Choncho, amene
^
5v
1 M'ndimeyi Mulungu akulangiza Asilamu kuti akhale opirira pa masautso
amtundu uliwonse amene akukumana nawo. Kupirira ndi chida chakuthwa
chopambanitsa munthu ndi kugonjetsera masautso. Munthu wosapirira ndi
zopweteka sangapambane pazofuna zake. Mulungu akutilangizanso kuti
tifunefune chithandizo pochulukitsanso Swala chifukwa chakuti Swala
imalimbikitsa mtima wa munthu pa masautso. Mtumiki (madalitso ndi mtendere
zikhale naye) ankati masautso akamkhudza amachita changu kukapemphera
Swala. Ndipo ankatinso, "Mulungu waupanga mpumulo wanga kukhala mkati
mwa Swala."
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
45
t *>»
t o^aJi i^y*
akukachita mapemphero a Haji ku
nyumbayo, kapena kuchita Umura,
Sikulakwa kwa iye kuzungulira
pamenepo (Pakati pamapiri
amenewo). Ndipo Amene achite
chabwino modzipereka
(Adzalipidwa). Ndithudi, Mulungu
Ngothokoza; Ngodziwa. 1
159. Ndithudi, amene akubisa
zimene tavumbulutsa Zomwe ndi
zisonyezo zoonekera poyera, ndi
Chiongoko pambuyo pozifotokoza
Mwatsatanetsatane kwa anthu
m'Buku, Mulungu
akuwatemberera iwo. Ndiponso
Akuwatemberera otemberera. 2
1 Haji ndi Umura ndimapemphero amene sangachitike pamalo pena paliponse
kupatula mumzinda wa Makka. Kachitidwe kamapemphero awiriwa
nkofanana. Koma pamakhala kusiyana pang'ono pakati pa Haji ndi Umura.
Kusiyana kwake kuli motere: Haji siichitika nthawi iliyonse koma m'miyezi
yake yodziwika. Ndipo kutha kwamiyezi ya Haji ndi masiku khumi am'khumi
loyamba am'mwezi wa Zuli Hija. Pomwe Umura ikhoza kuchitika m'mwezi
uliwonse umene munthu wafuna. Pa Umura palibe chinthu chimodzi
mwazinthu zomwe zimachitika m'mapemphero a Haji chomwe nkuimirira
pamalo otchedwa Arafat. Koma zina zomwe zimachitika pamapempherowa
nzofanana.
Zofunika pamapemphero a Haji ndi Umura ndi izi>
1. Kuzungulira Al-kaaba kasanu ndi kawiri (7)
2. Kuyenda mwandawala kasanu ndi kawiri pakati pamapiri awiri omwe ndi
Safaa ndi Marwa.
3. Kumeta kapena kuyepula tsitsi.
Pamapiripo Chisilamu chisanadze adaikapo mafano omwe anthu achikunja
panthawiyo adali kuwapembedza. Tero pamene Chisilamu chidadza Asilamu
ena sadali kuona bwino kukachitira mapemphero pamapiriwo poganizira
zamafano amene adalipo kalelo. Koma adawauza kuti palibe kuipa kulikonse
kuchitirapo mapemphero pamalopo chifukwa mafanowo adawachotsapo.
2 Nkofunika kwa munthu aliyense amene wachidziwa choona kuchita izi:-
a) Kuchivomereza choonacho.
b) Kuchitsata.
c) Kuchifalitsa.
d) Kuchiphunzitsa.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2 46 Y *jA-t
T SjiJ* 5jj-»
160. Kupatula amene alapa ndi
kukonza (Zolakwika)
nachilongosola (choonadicho Kwa
anthu), iwowo ndi amene
ndiwalandira Kulapa kwao. Ndipo
ine Ngolandira kulapa Kwambiri,
Ngwachisoni zedi.
161. Ndithudi, amene
sadakhulupirire, Namwalira ali
osakhulupirira, pa iwo Pali
matemberero a Mulungu, a Angelo
ndi A anthu onse.
162. M'menemo (m'chilango
cha matemberero) Adzakhalamo
mpaka muyaya. Ndipo chilango
Sichidzapeputsidwa kwa iwo,
ndipo Sadzapatsidwa nthawi
(yopumula).
163. Ndipo Mulungu wanu ndi
Mulungu mmodzi Basi. Palibe
wopembedzedwa mwachoonadi
Koma lye. Ngwachifundo
chambiri, Ngwachisoni. 1
y%\MM&f4\M
Choncho, masheikh ndi maulama ali ndi mwawi pokhala ndi ntchito
yapamwambayi. Achite ntchitoyi modzipereka kwatunthu, mwaulere kapena
molandira malipiro ngati alipo. Apitirize kuigwira ntchitoyi pamoyo wawo
wonse ngakhale atakumana ndi zovuta pantchitoyi. Ntchitoyi njomwe aneneri
a Mulungu adali kugwira. Tero aigwire motsanzira momwe aneneri a Mulungu
adali kuigwirira ntchitoyi pamakhalidwe awo ndi machitidwe awo onse. Kubisa
komwe kwanenedwa m'ndimeyi sikubisa mawu a Mulungu kokha, komanso
kubisa maphunziro azam'dziko ofunika kwa anthu.
Chisilamu chikulimbikitsa kuti ngati munthu akudziwa chilichonse chomwe
chili ndi phindu kwa anthu awaphunzitse anzake, asawabise chifukwa choopa
kuti nzeruyo angaitulukire anthu ambiri ndi kuti iye sadzapatsidwa ulemu
kapena kuopa kuti ena angampose. Maganizo otere ngosafunika
m'Chisilamu.
1 Tanthauzo la ndime iyi ndikuti Mulungu wanu Wompembedza ndi mmodzi.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2 47 Y *j£-i
Y o^dJt 5jj~-
164. Ndithudi, m'chilengedwe
chathambo ndi Nthaka, ndi
kusinthana kwa usiku ndi Usana,
ndi (kuyenda kwa) zombo zikulu
Zikulu zomwe zikuyenda panyanja
(Zitasenza zinthu) zothandiza
anthu, ndi Madzi amene Mulungu
Wawatsitsa kuchokera kumitambo,
naukitsira Nawo nthaka pambuyo
pokhala youma, Nawanditsa
m'menemo mtundu uliwonse wa
Nyama (chifukwa cha madziwo),
ndi M'kusinthanasinthana kwa
mphepo, ndi Mitambo yomwe
yalamulidwa Kuyenda pakati
pathambo ndi nthaka; Ndithudi,
(m'mzimenezo) muli zisonyezo
kwa Anthu anzeru, (kuti Mulungu
alipo).
165. Pali ena mwa anthu amene
akudzipangira Milungu naifanizira
ndi Mulungu. Amaikonda Monga
momwe akadamkondera Mulungu.
Koma Asilamu amene akhulupirira
Alibe mnzake wothandizana naye; alibe mwana alibe mkazi ndipo alibenso
makolo. Palibe wompembedza mwachoonadi padziko lonse lapansi
ndikumwamba koma lye yekha. lye Ngwachifundo chambiri, Wachisoni kwa
zolengedwa Zake; Woyera ndiponso Wotukuka pachikhalidwe Chake chonse.
Ndipo ali kutali ndi zimene akumunenerazo. Kodi asatukuke chotani kuzimene
akumunenerazo chikhalirecho lye ndi Yemwe adalenga thambo ndi zonse
zam'menemo monga nyenyezi zikuluzikulu zomwe zikuyenda m'menemo
mwadongosolo Lake lakuya popanda kuwombana ina ndi inzake. Ndipo
m'dziko lapansi adaikamo zolengedwa zambiri zododometsa zomwe
zikusonyeza mphamvu Zake zoposa, monga nyama zamoyo ndizomera
zosiyanasiyana mtundu, Ndi zopanda moyo ndi chikonzero
chawamphamvuyo. Ndipo zikuloza kuti alipo amene adazilenga ndi amene
akuziyang'anira yemwe ndi Mulungu. Dongosolo lazinthuzi likusonyeza kuti
Mulungu ndi mmodzi chifukwa chakuti pakadakhala anzake othandizana naye
pakadakhala chisokonezo, wina akadafuna china pomwe wina akufuna china.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2 48 t *>■»
Y 5jA-Jl 3jj--
Amamkonda Mulungu koposa.
Ndipo akadaona amene adzichitira
zoipa Pamene azikachiona
chilango (chomwe Awakonzera,
akadaona zoopsa; Zosasimbika).
Ndipo mphamvu zonse Nza
Mulungu. Ndipo Mulungu
ngolanga Mwaukali.
166. (Akumbutse) nthawi imene
otsatidwa Adzakana amene adali
kuwatsata uku Atachiona chilango.
Ndipo mgwirizano Wapakati pawo
udzaduka.
167. Ndipo otsatirawo adzati:
"Kukadakhala Kotheka kwa ife
kubwerera (kumoyo Wapadziko)
tikadawakana monga iwo
Atikanira." Umo ndi momwe
Mulungu Adzikawaonetsera
zochita zawo kukhala Madandaulo
awo. Ndipo iwo Sadzatulukanso
kumoto.
168. E inu anthu! Idyani
zabwino zimene zili M'nthaka
zomwe zili zololedwa; Ndipo
musatsate mapazi a Satana. lye
Kwa inu ndi mdani woonekeratu.
169. lye akukulamulani kuchita
zinthu Zoipa ndi zauve. Ndikuti
»j£
1 E inu anthu! Idyani zamdziko lapansi zomwe zili zabwino zimene Mulungu
wakulolezani ndipo musapenekere chilolezo chake. Musadye chinthu
chosaloledwa monga kudya chinthu chawina m'njira yachinyengo.
Musakhwathule chuma chamnzanu.
Ndipo chenjerani ndi njira za Satana yemwe amakukometserani zoipa.
Dziwani kuti iyeyu ndi mdani wanu monga adalili mdani watate wanu Adamu.
Dziwaninso kuti iye salamula kuchita zabwino koma zoipa zokhazokha.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
49
t *>i
t djiJl 3jj-»
Mumnamizire Mulungu
pomunenera zimene
Simukuzidziwa.
170. Ndipo kukanenedwa kwa
iwo (kuti): "Tsatirani zimene
Mulungu wavumbulutsa;"
Akunena: "Koma tikutsata zimene
Tidawapeza nazo atate athu." Kodi
Ngakhale kuti atate awo sadali
kuzindikira Chilichonse ndiponso
sadali oongoka? (Awatsatirabe)? 1
171. Ndipo fanizo la amene
sadakhulupirire (omwe
Akulalikidwa mawu a Mulungu,
ndi makani Awo) lili ngati (mbusa)
yemwe akukuwira Ziweto zake ndi
kuzikalipira pomwe izo Sizimva
tanthauzo lamawu oitanawo, Koma
kuitana (chabe) ndi kufuula. (Iwo)
Ndi agonthi, abubu ndi akhungu.
Tero Iwo sangazindikire.
172. E inu amene
mwakhulupirira! Idyani zinthu
zabwino zimene Takupatsani,
ndipo yamikani Mulungu ngatidi
inu Mukupembedza lye yekha.
173. lye akukuletsani (kudya)
nyama Zakufa zokha, liwende,
\t\fote
Chikhulupiriro chamunthu kuti chikhale champhamvu ndi chopindula
pafunika kuti achidziwe bwinobwino chimene akuchikhulupiriracho.
Asangotsatira ndikuchikhulupirira chifukwa choti auje ndi auje adali
kuchikhulupirira chimenecho. Zinthu zotere zimawasokeretsa anthu ambiri.
Anthu ena amachikhulupirira chinthu chifukwa chakuti makolo awo adali
kuchikhulupirira pomwe chinthucho chiii chachabe.
Mulungu adatipatsa dalitso lanzeru kuti tizirigwilitsira ntchito pofuna choonadi
chazinthu, osati kumangotsatira ngati wakhungu.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
50
Y tjtr\
V djiJ\ djy^
6\
nyama Yankhumba ndi nyama
Yodulidwa poikuwira mayina
Amafano kusiya Mulungu. Koma
amene Wasimidwa (nadya
choletsedwacho) popanda
Kuchikhumba choletsedwacho ndi
mosapyoza Muyeso palibe tchimo
kwa iye. Ndithudi, Mulungu
Ngokhululuka kwambiri,
Ngwachisoni zedi. 1
174. Ndithudi, amene akubisa
zomwe Mulungu Adavumbulutsa
m'buku (la Baibulo) M'malo
mwake nasankha zinthu zamtengo
Wochepa, iwo sadya china
mmimba mwawo Koma moto basi;
ndipo Mulungu Sadzawayankhula
tsiku Lachimaliziro (mwachifundo
Koma mokwiya); Ndipo
sadzawayeretsa. Ndipo iwo
Adzapeza chilango chopweteka. 2
1 Apa Mulungu akutiuza kuti zinthu zinaizi nzoletsedwa kudya koma ngati
munthu atavutika kwambiri ndi njala yofuna kufanayo, akumlola kuzidya
pamuyeso wothetsa njalayo, osati mokhutitsa.
Chimene chadulidwa pochitchulira dzina lomwe si la Mulungu monga nyama
zomwe zikuzingidwira kukwanitsa maloto aazimu, kapena yomwe yazingidwa
chifukwa chotsilika nyumba, kapena kutsilika midzi, ndi zina zomwe
zikuzingidwa kuti eti Satana asawavutitse; zonsezi nzoletsedwa.
2 Ibunu Abbas adati ndime iyi ikufotokoza za atsogoleri a Chiyuda monga
Kaabi bun Ashirafi ndi Maliki bun Swaifi ndi Huyaye bun Akhatwabi. Anthuwa
adali kulandira mphatso zambiri zochokera kwa anthu awo owatsatira.
Pamene Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale naye) adampatsa
uneneri iwo sadakhulupirire chifukwa choopa kuti sapeza mitulo yochokera
kwa anthu awo. Tero anabisa kwa anthu za uneneri wa Muhammad
(madalitso ndi mtendere zikhale naye) Apa mpamene Mulungu
adavumbulutsa aya (ndime) iyi, yakuti "Ndithudi, amene akubisa zomwe
Mulungu adavumbulutsa m'Buku (la Baibulo) m'malo mwake nasankha zinthu
zamtengo wochepa iwo sadya china m'mimba mwawo koma moto basi".
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
51
y *>i
Y o^iJt 3jj-*>
175. Iwo ndi amene asinthanitsa
Kusochera ndi chiongoko
Ndiponso chilango ndi
Chikhululuko. Kodi Ndi chiyani
chikuwachititsa Kukhala opirira
ndi moto.
176. Zimenezo nchifukwa
chakuti Mulungu Adavumbulutsa
Buku lake mwachoonadi (Ndipo
iwo adalikana). Koma amene
Asemphana m'Bukumo ali
munkangano Wonkera nawo kutali
kusiya choonadi
177. Ubwino suli potembenuzira
Nkhope zanu mbali yakuvuma Ndi
kuzambwe (Popemphera Swala);
koma ubwino Weniweni ndi
(waomwe) Akukhulupirira
Mulungu, Tsiku lomaliza, Angelo
ndi Buku, ndi Aneneri; napereka
Chuma, uku eni akuchifunabe,
Kwa achibale ndi amasiye, Ndi
masikini ndi apaulendo (omwe
Alibe choyendera), ndi opempha,
Ndikuombolera akapolo;
napemphera Swala, napereka
chopereka (Zakati); Ndi
okwaniritsa malonjezo awo
Akalonjeza, ndi opirira Ndi
umphawi ndi matenda ndi
Panthawi yankhondo. Iwo wo ndi
Amene atsimikiza (Chisilamu
chawo). Ndiponso iwo wo ndi
Omwe ali oopa Mulungu.
Siirat 2. Al-Baqarah Juzu 2 52 * *jJH
t o^iJl 5jj*-
178. E inu amene
mwakhulupirira! Kwalamulidwa
Kwa inu kubwezerana molingana
kwa ophedwa; Mfulu kwa mfulu,
kapolo kwa Kapolo, mkazi kwa
mkazi. Koma amene
wakhululukidwa ndi M'bale
wakeyo pachinthu Chilichonse,
atsatire ndi kulonjerera dipolo
Mwaubwino. (Nayenso wolipa)
apereke kwa lye mwaubwino.
Kumeneko ndikufewetsa Kumene
kwachokera kwa mbuye wanu,
Ndiponso chifundo. Ndipo amene
alumphe Malire pambuyo paizi,
iye Adzapeza chilango
chopweteka. !
'<h% '*"*%*'+ 9*<9 9>Z < k V
Apa akunena kuti, "mfulu kwa mfulu" kuthanthauza kuti aliyense amene
wapha nayenso aphedwe. Sikuti aphe munthu wina m'malo mwake.
Chisilamu chisanadze kudali kuponderezana zedi. Mfulu yochokera kufuko
lapamwamba. Ngati atapha mfulu yafuko lapansi eni awakuphayo adali
kukana kumpereka kuti aphedwe. M'malo mwake amapereka kapolo kuti
ndiye aphedwe m'malo mwake. Kapolo wamfulu lapamwamba akapha kapolo
wamfulu lapansi sadali kumpereka kuti akaphedwe. Amati; "Kapolo wathuyo
ngwapamwamba pomwe wanuyo ngonyozeka. Choncho palibe kufanana
pakati pa awiriwa." Ndipo ngati zitachitika motere kuti kapolo waonyozeka
nkupha kapolo waodzitukumula, odzitukumulawa amakana kupha kapolo uja
m'malo mwake amafuna mfulu yochokera kufuko lonyozekalo. Tero Kurani
idaletsa machitidwe oterewa. Anthu onse ngofanana, palibe kusiyana pakati
pawo. Amene wapha aphedwe yemweyo osati wina, ngakhale atakhala mfulu
kapena kapolo. Hi ndilo tanthauzo la aya (ndime) imeneyi.
Tsono gawo lina limene likuti "Koma amene wakhululukidwa ndi mbale
wakeyo..." tanthauzo lake nkuti amene wamphera mbale wake
akamkhululukira wakuphayo amlipiritse dipo landalama. Tero apa akumuuza
iyeyo kuti ngati atamkhululukira m'bale wakeyo nangomulipiritsa ndalama,
alonjerere dipolo mwaubwino. Nayenso wolipayo apereke mwaubwino.
Asachedwetse mwadala namzunguzazunguza. Tsono gawo lachitatu landime
yokhayokhayi likutiuza za chifundo chimene Mulungu watichitira potilekera ife
eni kusankha chiweruzo pankhaniyi.
Munthu yemwe amphera mbale wake akhoza kuchita izi:
a) Kuuza Boma kuti liphenso yemwe adapha mbale wakeyo.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
53
r *>i
t ljAS\ 5jj-*»
179. Mkubwezerana kofanana
muli kusunga moyo kwa inu, e!,
Inu eni nzeru! Kuti
Mudzitchinjirize (kumchitidwe
ophana) 1
180. Kwalamulidwa kwa inu
kuti mmodzi wanu imfa
ikamuyandikira, Ngati asiya
chuma, Apereke malangizo (pa
zachumacho) Kwa makolo ake
awiri ndi Achibale ake,
mwaubwino. Ichi nchilamulo Kwa
oopa Mulungu.
181. Ndipo amene asinthe
malangizowo Pambuyo
pakuwamva; Utchimo wake uli pa
Amene akusinthawo. Ndithudi,
Mulungu Ngwakumva;
Ngodziwa. 3
<$&M&J®8&$
b) Kapena kumlipiritsa dipo.
c) Kapena kumkhululukira popanda kulipa chilichonse.
Ndipo gawo lomaliza landimeyi akumchenjeza wokhululukayo kuti
asangomkhululukira munthuyo pamaso pa anthu kenako nkumachita chiwembu
mobisa.
1 Muli moyo wabwino m'machitidwe abwino chifukwa chakuti potsata zimenezi
aliyense adzakhala wotsata mwambo. Adzaopa kuti ngati apha mnzake
nayenso aphedwa. Ngati achitira mnzake choipa nayenso amchitira choipa.
Tero popewa zopwetekazo akhala ngati akusunga miyoyo ya anthu ena ndi
wake womwe.
2 Kale malamulo ogawira chuma cha masiye asanafotokozedwe adampatsa
ufulu aliyense kuti alembe wasiya (will) pazachuma chakecho m'mene mwini
angaonere. Wasiyawo ukhale m'njira yachilungamo yolingana ndi Shariya.
Asachite chinyengo chamtundu uliwonse.
3 Apa akuwachenjeza amene auzidwa wasiyawo kuti asasinthepo kanthu.
Ndipo akunenetsa kuti ngati wasiyawo uwonongedwa ndiye kuti anthu omwe
adalandira wasiyawo akhala ndi uchimo chifukwa chosintha wasiyawo. Koma
ngati wasiyawo udalembedwa mopanda chilungamo, monga kuti iye adati
"Chuma changa m'dzawapatse ana anga aamuna okha basi" nkusiya
kutchulapo aakazi, apo Mulungu akuloleza olandira wasiyawo kuti aukonze
ndikuwagawira ana onsewo mwachilungamo.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
54
T t-jir\
T OjiJl 9jj--
182. Ndipo amene waopa kuti
mwini wakeyo (Wopereka 'will'
kapena waswiya) Angapendekere
kumbali yokhota kapena
Kuuchimo, nalinganiza pakati
pawo, palibe Tchimo kwa iye.
Ndithudi, Mulungu ngokhululuka
zedi, Ngwachifundo chambiri.
183. E inu amene
mwakhulupirira! Kwalamulidwa
kwa inu kusala (Ramadhani)
monga momwe Kudalamulidwira
kwa anthu Akale, inu
musadabwere kuti Muope
Mulungu (popewa Zoletsedwa).
184. (Kusalaku nkwa) masiku
owerengeka. Koma amene akhale
odwala mwa Inu kapena kukhala
paulendo, (Namasula masiku ena),
Akwaniritse chiwerengerocho
NT masiku ena. Ndipo kwa amene
Sangathe kusala chifukwa
Chaukalamba apereke dipo
lodyetsa Masikini. Ndipo amene
achite zabwino Mwachifuniro
chake, kutero ndibwino Kwa iye.
Ndipo kusala (pamene
Kukulolezedwa kumasula)
Ndibwino kwa inu, ngati Muli
odziwadi (kufunika kwa kusala). 1
1 Amene sangathe kusala ndi awa:-
a) Okalamba kwambiri omwe abwerera kuumwana, amene sangathe kupilira
ndi njala
b) Odwala amene sangathe kusala ndipo alibe chiyembekezo choti achira,
monga amene ali ndi matenda a "Cancer" kapena "High Blood Pressure"
- ' f< "' l? %^%
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
55
X *jJM
V 5yL)l 5jj-*»
185. (Mwezi uwu
mwalamulidwa Kusala ndi )
mwezi wa Ramadhani Womwe
mkati mwake Qur'an
Idavumbulutsidwa kuti ikhale
chiongoko Kwa anthu ndi
zizindikiro zoonekera Poyera
zachiongoko. Ndikutinso ikhale
cholekanitsa (Pakati pachoonadi
ndi bodza) Ndipo mwa inu amene
akhalepo (Pamudzi) M'mweziwu,
amange. Koma amene ali
wodwala, Kapena ali paulendo,
akwaniritse Chiwerengero
m'masiku ena (Cha masiku amene
Sadasale). Mulungu akukufunirani
Zofewa, ndipo sakukufunirani
zovuta. Ndipo kwaniritsani
kapena matenda a "Sugar". Anthu oterewa akuloledwa kusiya kumanga.
Ndipo tsiku lililonse aliyense waiwo apereke chakudya choposera Vzkg.
Chakudya chomwe anthu m'dzikomo amadya. Koma amene ali osauka
asachite zimenezi.
Mulungu amkhululukira pakuti Mulungu sakakamiza munthu kuchita chimene
sangathe kuchichita.
1. Tsono wodwala yemwe ali ndi chiyembekezo chochira.
2. Ndi wapakati amene akuvutika ndi kusala.
3. Ndi woyamwitsa amene akuona kuti azunzika akasala, onsewa sapereka
dipo lija.
Koma adzalipa masiku amene adamasulawo zikawachokera zovutazo
monganso zilili ndi wapaulendo. Koma masheikh ena akuti wapakati ndi
woyamwitsa nawonso apereke dipo lachakudya. Tero malangizo awanso
tikhoza kuwatsata.
Tsono kunena koti: "Ngati mutasala ndi bwino kwainu"... kukusonyeza kuti
kumanga silamulo lomwe Mulungu watikakamiza kuchita lopanda phindu
kwaife, koma nchinthu chothandiza kwa anthu, makamaka pathupi lathu.
Ndipo kuonjezera apa, Mulungu, pa tsiku la chimaliziro, adzatipatsa mphoto
yabwino. Masiku ano madokotala onse padziko lapansi akuvomereza kuti
kusala kuli ndi phindu laltkulu kuthupi lamunthu. Ichi ndi chimodzi
mwazizindikiro zosonyeza kuona kwa chipembedzo cha Chisilamu.
Chinenere nkhaniyi papita zaka zoposa chikwi chimodzi ndi mazana anayi
(1 ,400) ndipo tsopano omwe sali Asilamu akuvomereza.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
56
t *>»
t SjSJl djj--
chiwerengerocho Ndi
kumlemekeza Mulungu Chifukwa
chakuti wakutsogolerani
Ndikutinso mukhale othokoza. ]
186. Ndipo akapolo anga
akakufunsa za ine, (Auze kuti) Ine
ndili pafupi nawo. Ndimayankha
zopempha zawopempha pamene
Akundipempha. Choncho iwo
ayankhe Kuitana kwanga ndipo
andikhulupirire Kuti aongoke. 2
187. Kwaloledwa kwa inu
muusiku wosala Kukumana ndi
akazi anu. Iwo ali ngati Chovala
chanu. Inunso muli ngati chovala
Chawo. Mulungu wadziwa kuti
mudali Kudzichitira chinyengo
nokha. Choncho Walandira kulapa
kwanu ndipo Wakukhululukirani.
Tsopano khudzanani nawo Ndipo
funani chimene Mulungu
wakulamulirani, Ndipo idyani ndi
kumwa mpaka kudziwike
Bwinobwino kwa inu kuyera kwa
mbandakucha Ndi kuda kwa
1 Mulungu akufuna kuti tikwaniritse chiwerengero chamasiku makumi atatu
(30) kapena makumi awiri ndi mphambu zisanu ndi zinayi (29) chifukwa choti
phindu lakumanga silingapezeke mthupi lamunthu pokhapokha kumangaku
kutakwaniritsidwa m'masiku amenewa.
Mulungu akufuna kuti timthokoze paufulu wakewu umene watichitira
potilamula kuchita chilichonse chodzetsa chabwino kwaife ndikutiletsa
zodzetsa mavuto kwa iye.
2 Sikuti iwe wekha ndiwe uzipempha Mulungu kuti "Ndipatseni chakuti;
nchiritseni kumatenda akutiakuti" pomwe iwe suvomera kuitana kwa Mulungu
poleka zimene akukuletsa ndi kutsata zimene akukulamula. Yamba
kumuvomera Mulungu usanayambe kumpempha ndiye kuti pempho lako
lidzakhala laphindu.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
57
t *>»
t SjaJi djj--
mdima wausiku; (kufikira Mdziwe
kuti kucha kwalowa, usiku watha).
Kenako kwaniritsani kusala mpaka
dzuwa Litalowa. Ndipo
musakhudzane nawo (akazi Anu)
pamene inu mukuchita mbindikiro
M'misikiti. Amenewo ndi malire a
Mulungu; Choncho
musaayandikire. Motere ndimo
Mulungu akulongosola
Mwatsatanetsatane zisonyezo zake
kwa anthu Kuti akhale oopa
Mulungu (potsatira malamulo Ake
ndi kusiya zoletsedwa). 1
188. Ndipo musadye chuma
chanu Pakati panu Mwachinyengo
Pochipereka kwa oweruza (M'njira
ya ziphuphu) ndi cholinga Choti
mudye gawo la chuma Cha anthu
mwatchimo Uku inu mukudziwa.
189, Akukufunsa zamiyezi
Nena: "Imeneyi ndi miyeso
•,i<*6,UiU
&&>$-$\&-&&s
1 Pachiyambi pomwe lamulo lakumanga lidakhazikitsidwa adawaletsa anthu
kukumana ndi akazi awo usiku pambuyo poti iwo agona tulo ngakhale kuti
angogona pang'ono pokha. Kukumana ndi mkazi akumane asanagone. Tero
tamuloli lidali lovuta kwambiri kwa iwo kulitsata. Ena a iwo adalakwa
pang'ono. Choncho kudalengezedwa kuti "Tsopano pali chilolezo choti
akhoza kuchita chilichonse mpaka m'mbandakucha. Ndipo kunena koti
"Funani chimene Mulungu wakulamulani" ndi kulilimbikitsa lamulo
kuchilolezocho. Musati kuti poti kale adakuletsani kukumana ndi akazi anu
pambuyo pogona tulo ndiye mupitiriza kutero - iyayi. Koma tsatirani
chilolezocho.
"Itikafu" ndikuchita chitsimikizo munthu chokhala mumsikiti kwamasiku akuti-
akuti kapena nthawi yakutiyakuti. Ndipo pempheroli limachitika nthawi zambiri
m'mwezi wa Ramadhani. akachita chitsimikizocho (niya) saloledwa kutuluka
mumsikitimo pokhapokha patakhala chifukwa chachikulu chotulukira, monga
kupita kukadzithandiza. Panthawi yoti munthu ali papemphero la Itikafu
saloledwa kukumana ndi mkazi wake m'njira yaukwati ngakhale panthawi
yomwe akupita kukadzithandiza.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
58
1 *>-1
t 6jiS\ 6jJ~-
yanthawi Yozindikira anthu zinthu
zawo Ndi nthawi ya Haji". Ndipo
Siubwino kulowera m'nyumba
Zanu mbali yakumbuyo kwake.
Koma ubwino ndiyemwe Akuopa
Mulungu. Ndipo lowerani
M'nyumba podzera irf makomo
ake. Opani Mulungu kuti inu
mupambane. 1
190. Ndipo menyani nkhondo pa
njira ya Mulungu (Modziteteza)
ndi amene Akukuthirani nkhondo.
Koma Musalumphe malire
(kumenya Amene sadakuputeni),
chifukwa chakuti Mulungu
sakonda olumpha malire. 2
191. Ndipo apheni (amene
akukuthirani nkhondo Popanda
chifukwa) paliponse pamene
Mwawapeza; ndipo atulutseni
paliponse Pamene adakutulutsani;
chifukwa Kusokoneza anthu pa
chipembedzo chawo Nkoipitsitsa
zedi kuposa kupha. Koma
Musamenyane nawo pafupi ndi
Msikiti Woyera pokhapokha
%j» A**
M'nthawi yaumbuli anthu ankati akalowa m'mapemphero a Haji sadali
kulowa m'nyumba zawo podzera pakhomo. Ndipo sadalinso kutulukira
pakhomo koma amaboola chibowo kuseri kwanyumba nkumalowerapo ndi
kutulukirapo namaganiza kuti kutero ndimapemphero okondweretsa Mulungu.
Tsono apa Mulungu akuletsa machitidwe amenewo.
2 lyi ndiimodzi mwandime zomwe zikufotokoza bodza la amene akunena kuti
Chisilamu chidafala ndi lupanga powathira anthu nkhondo mowapondereza
kuti alowe m'chisilamu.
Limeneli, ndithu, ndibodza lamkunkhuniza. Apa pakuonetsa kuti Mulungu
akuwapatsa chilolezo Asilamu kuti amenyane ndi amene akuwaputa. Palibe
chilolezo kwa iwo chomenyerana ndi anthu osawaputa.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2 59 t *j*-i
t 5yJi 5jj-*»
atayamba ndiwo Kukumenyani
pamenepo.Ngati atamenyana Nanu
pamenepo, inunso menyananaoni.
Motero ndi momwe ilili mphoto ya
Osakhulupirira.
192. Koma ngati asiya, ndithudi
Mulungu Ngokhululuka,
Ngwachifundo kwabasi.
193. Ndipo menyananaoni
kufikira pasakhale Masautso
(ochokera kwa iwo powasautsa
Asilamu popanda chifukwa).
Ndipo Chipembedzo chikhale cha
Mulungu (osati Kupembedza
anthu).Koma ngati asiya,
Pasakhale mtopola kupatula kwa
okhawo Amene ali ochita zoipa.
194. Mwezi wopatulika kwa
mwezi wopatulika; Ndipo zinthu
zopatulika paikidwa Kubwezerana.
Ndipo amene wakuchitirani
Mtopola, inunso mchitireni
mtopola Molingana ndi momwe
wakuchitirani Mtopola, ndipo
opani Mulungu (musapyoze
Kuposa momwe wakuchitirani).
Ndipo Dziwani kuti Mulungu ali
pamodzi ndi oopa.
195. Ndipo perekani chuma
chanu pa njira ya Mulungu,
ndiponso musadziponye
Kuchionongeko ndi manja anu;
chitani Zabwino. Ndithudi,
Mulungu amakonda Ochita
zabwino.
Surat 2. AI-Baqarah Juzu 2
60
t *>i
t oyUl ^JJ- -
196. Ndipo kwaniritsani Haji
ndi Umura chifukwa Chofuna
kukondweretsa Mulungu. (Izi zili
Mkutsimikiza kulowa
m'mapemphero a Haji). Ndipo
ngati mutatsekerezedwa
(kukwaniritsa Mapemphero),
Choncho zingani nyama Zimene
zili zosavuta kuzipeza (monga
Mbuzi), ndipo musamete mitu
Yanu kufikira nsembeyo ifike
Pamalo pake pozingirapo (pomwe
ndi pamalo Pamene
mwatsekerezedwapo). Ndipo
amene Mwa inu ali odwala kapena
ali ndi zovutitsa Kumutu kwake,
(nachita zomwe zidali Zoletsedwa
monga kumeta) apereke dipo
Lakumanga kapena kupereka
sadaka , kapena Kuzinga nyama.
Ndipo ngati muli pamtendere,
Choncho amene adadzisangalatsa
pochita Umura kenako nkuchita
Haji, Azinge nyama imene ili
Yosavuta kupezeka (monga
mbuzi). Ndipo Amene sadapeze,
asale masiku atatu konko Kuhajiko
ndipo asalenso masiku Asanu ndi
awiri mutabwerera Kwanu.
Amenewo ndi masiku Khumi
okwanira. Lamuloli nlayemwe
banja Lake silili pafupi ndi Msikiti
wopatulika. Ndipo Opani
Mulungu, dziwani kuti Mulungu
Ngwaukali polanga.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
61
1 *>i
T 5jiJl 5jj-j
197. (Mapemphero a) Haji ali
ndi miyezi Yodziwika, (yomwe
ndi: Shawali, Zuli Kada ndi Zuli
Hija). Amene Watsimikiza kuchita
Haji (m' miyezi)
Imeneyo,asayankhule zauve,
asachite Zauve, ndiponso
asapandukire malamulo (Pochita
zoletsedwa uku iye ali m'mape-
Mphero a Haji), ndiponso
asakangane ali M'Hajimo. Ndipo
chabwino chilichonse Chimene
mungachite, Mulungu achidziwa.
Ndipo dzikonzereni kamba
wapaulendo, ndithu Kamba
wabwino (wadziko lapansi) ndi
amene Angakupewetseni
kupemphapempha. (Koma Kamba
wabwino wa tsiku lomaliza ndiko
kuopa Mulungu). Choncho
ndiopeni inu eni nzeru.
198. Sikulakwa kwa inu
kufunafuna zabwino za Mbuye
wanu (pogulitsa zinthu zanu uku
Muli m'mapemphero a Haji,
kapena kugula). Ndipo
mukabwerera kuchokera ku Arafat,
Tamandani Mulungu pamalo
otchedwa Mashari Harami
(Muzidalifa). Ndipo
Mukumbukireni monga Momwe
adakutsogolerani. Ndithudi, kale
Mudali mwaosokera.
199. Kenako yendani limodzi
kuchokera pamalo Pamene
edS8\
<jb>[j \ £oI> £-* tj-<&g I
Siirat 2. Al-Baqarah Juzu 2
62
Y *>i
Y 3jaJ* $jj~>
akuchokerapo anthu onse (pomwe
Ndi pa Arafat), ndipo pemphani
Chikhululuko kwa Mulungu.
Ndithudi, Mulungu Ngokhululuka
kwambiri, Ngwachisoni zedi.
200. Ndipo mukamaliza
mapemphero anu (tsiku La Idi
komwe ndikuponya sangalawe,
kuzinga Nyama zansembe, kumeta
ndi kuzungulira Kaaba {Tawafu-li-
Ifaza}), mtamandeni Mulungu
Monga momwe mudali
kutamandira makolo anu Kapena
mtamandeni koposa.Ndipo alipo
ena Mwa anthu amene akunena
(kuti): "O! Mbuye Wathu!
Tipatseni padziko lapansi:" Ndipo
Iwo alibe gawo lililonse pa tsiku
lomaliza.
201. Ndipo alipo ena mwa iwo
omwe akunena kuti: "O! Mbuye
wathu! Tipatseni (mtendere)
padziko Lapansi ndipo patsiku
lomaliza Mudzatipatsenso
zabwino, ndikutitchinjiriza ku
Chilango chamoto!"
202. Iwo ndi amene adzapeza
gawo lazimene Adapata; ndipo
Mulungu ngwachangu
Pakuwerengera.
203. Ndipo mtamandeni
Mulungu m'masiku
Owerengekawo. Koma amene
wachita Changu pamasiku awiri
/),
a&i^&iu^iij-tDt
<99 '199% <
"Z9I9 '*~\<r<
\f' £* h 9 ?~<> * <i 9^9 '
4 *
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2 63 Y ^
Y S^iJl djj-*»
okha (nabwerera Kwawo) palibe
tchimo pa iye. Ndipo amene
Wachedwerapo palibenso tchimo
pa iye kwa Amene akuopa
Mulungu. Choncho opani
Mulungu, ndipo dziwani kuti kwa
Iye nkumene
Mudzasonkhanitsidwa.
204. Ndipo mwa anthu alipo
amene zoyankhula Zake
zikukondweretsa (iwe) pano
padziko Lapansi, (koma tsiku
lomaliza kuipa kwake
Kudzadziwika). Ndipo iye
akutsimikizira Mulungu kuti
akhale mboni pa zomwe zili
Mumtima mwake pomwe Iye ndi
wa makani kwambiri. 1
205. Koma akachoka (kwa iwe)
akuyenda padziko (Uku ndi uku)
ncholinga chofuna kuyipitsapo ndi
kuononga zomera ndi miyoyo.
Komatu Mulungu Sakonda
kuononga.
206. Ndipo akauzidwa kuti:
"Opa Mulungu", Akugwidwa ndi
mwano womupititsa Kumachimo,
Tanthauzo lake nkuti alipo ena mwa anthu omwe angakukometsere
zoyankhula zawo ndikuthwa kwa lirime lawo pomwe iwo chikhalirecho
akungoyankhula kuti apeze zinthu zam'dziko.
Ndimeyi ikufotokoza za Al Akhnas bun Shariki yemwe amati akakumana ndi
mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye), amatamanda ndi kusonyeza
chikhulupiriro chabodza. Koma akachoka pamaso pa mtumiki (madalitso ndi
mtendere zikhale naye) amayenda padziko ncholinga choononga.
Umo ndi momwe alili makhalidwe a anthu ena, amangokometsa mawu
pomwe zochita zawo nzauve. Tero tichenjere ndi anthu otere.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2 64 * *>»
Y SjiJl Oj^-»
choncho Jahanama Ikukwana kwa
iye (Kuwuchotsa mwano
wakewo); Aipirenji malo
okonzeredwa.
207. Pali wina mwa anthu
amene Akugulitsa mzimu wake
chifukwa Chofuna chiyanjo cha
Mulungu; Ndipo Mulungu
ngodekha Kwa akapolo Ake.
208. E inu amene
mwakhulupirira! Lowani
m'chisilamu Chonse ndipo
musatsatire Mapazi a Satana. Iye
ndi mdani wanu Woonekeratu
poyera. *
209. Ndipo ngati mutaterezuka
(Kuchimwa) pambuyo
Pokudzerani zisonyezo Za
Mulungu zoonekera poyera,
Dziwani kuti Mulungu
Ngwamphamvu zoposa;
Ngwanzeru zakuya.
210. Kodi pali china chimene
Akuyembekeza osati Kuwadzera
Mulungu m'mithunzi Ya mitambo
ndi (kuwadzera) Angero;
nkuweruzidwa chilamulo
(Chakuonongeka kwawo)?
©a#<£#
E! inu amene mwakhulupirira! Inu eni mabuku, gonjerani Mulungu. Ndipo
lowani m'Chisilamu kwathunthu posachisokoneza ndi chinachache.
Mawuwa adanenedwa pamene Abdullahi bun Salaami adalowa m'Chisilamu
yemwe adali mkulu wa chiyuda. lye adapempha chilolezo kwa mtumiki
(madalitso ndi mtendere zikhale naye) kuti aziliremekezabe Tsiku la Sabata
(la chiweru) ndi kuti aziwerenga mawu am'Taurati m'swala zake zausiku.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
65
X *>-»
X o^iJl 5jj*rf
Komatu zinthu zonse
zimabwezedwa Kwa Mulungu.
211. Afunse ana a Israeli kuti
Ndizizindikiro zingati zopenyeka
Zomwe tidawapatsa? Komatu
amene angasinthe chisomo Cha
Mulungu pambuyo pomudzera,
(Mulungu adzamulanga). Ndithudi,
Mulungu ngolanga mwaukali.
212. Moyo wapadziko lapansi
wakometsedwa Kwa amene
sadakhulupirire, ndipo
Amawachitira Chipongwe amene
Akhulupirira. Koma amene Aopa
Mulungu adzakhala Pamwamba
pawo tsiku la Chiweruzo, ndipo
Mulungu Amapatsa amene
wamfuna Popanda chiwerengero.
213. Anthu onse adali ampingo
umodzi (Wa Chisilamu panthawi
ya Adamu kufikira Nuhi kenako
Adayamba kupatukana), ndipo
Mulungu Adatumiza aneneri
Onena nkhani zabwino ndi
Oteteza; ndipo pamodzi nawo
Adavumbulutsa Mabuku
achoonadi Kuti aweruzire pakati
Pa anthu pazimene adalekana.
Ndipo Sadalekane pazimenezo
koma aja amene Adapatsidwa
mabukuwo pambuyo Powadzera
Zizindikiro zoonekera poyera,
Chifukwa Chakuchitirana dumbo
pakati pawo. Koma Mulungu
adawaongolera amene
U>!5 {&&** &&£* WS^I
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
66
t >>i
t S^iJl Ijj^
Adakhulupirira kuchoonadi
chazomwe Adalekaniranazo,
Mwachifuniro chake. Ndipo
Mulungu amamutsogolera kunjira
Yolunjika amene wamfuna.
214. Kodi mukuganiza kuti
mukalowa Kumunda wa mtendere
pomwe Sanakudzereni masautso
Olingana (ndiomwe) adawapeza
Amene adamuka kale inu
musanabadwe? Kusauka ndi
matenda Zidawakhudza, ndipo
adawanjenjemeretsa Koopsa
kufikira Mtumiki pamodzi Ndi
amene Adakhulupirira naye adati:
"Chipulumutso cha Mulungu
chibwera liti?" Dziwani kuti ndithu
Chipulumutso Cha Mulungu chili
pafupi! 1
215. Akukufunsa kuti apereke
chiyani? Nena: "Chuma
chilichonse chimene
Mungachipereke, (Chiperekeni)
kwa Makolo awiri, achibale, kwa
ana Amasiye, kwa osauka, ndi kwa
apaulendo. Ndipo chabwino
chilichonse chimene Mungachite,
ndithudi, Mulungu akuchidziwa. 2
1 Apa Mulungu akufotokoza kuti Msilamu aliyense adzapeza mavuto pokwaniritsa
Chisilamu chake. Palibe chinthu chopindulitsa chimene chimangopezeka
mofewa. Mavuto ndi amene amamkonza munthu kuti akhale olimba.
Choncho, munthu asaganize kuti adzapeza chinthu chamtengo wapatali
popanda kuchivutikira.
Adafunsa izi lisanadze lamulo lakagawidwe kachuma chamasiye. Pamane
lidadza lamulo lakagawidwe kachuma chamasiye lidaletsa kupereka chilawo
(wasiya) kwa anthu owagawira chumacho. Nchifukwa chakuti aliyense waiwo
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
67
t *>»
t SyLJi 5jj-*
216. Kwalamulidwa kwa inu
kumenya Nkhondo ( Yotetezera
chipembedzo Cha Mulungu)
pomwe iyo (nkhondoyo)
Njodedwa ndi inu. Komatu Mwina
mungachide chinthu pomwe Icho
chili Chabwino kwainu. Mwinanso
mungakonde Chinthu pomwe icho
chili choipa Kwainu. Koma
Mulungu ndiyemwe Akudziwa.
Ndipo inu simudziwa.
217. Akukufunsa (zalamulo la)
kumenya Nkhondo M'miyezi
yopatulika. Nena: "Kumenya
Nkhondo m'miyeziyo Nditchimo
lalikulu. Komatu Kuwatsekereza
anthu kuchipembedzo Cha
Mulungu, ndi kumkana Mulungu,
(ndi Kuletsa anthu) kumsikiti
wopatulikawo, Ndi kutulutsa anthu
m'menemo nditchimo Loposa kwa
Mulungu. Ndipo kutsekereza anthu
kuchipembedzo chawo nzoipa
Kwabasi kuposa kupha. Ndipo
sasiya Kumenyana nanu kufikira
akuchotseni M' chipembedzo
chanu ngati angathe. Ndipo
mwainu amene atuluke
m' chipembedzo Chake, kenako
namwalira uku ali Osakhulipirira,
iwo ndi omwe ntchito zawo
Zaonongeka padziko lapansi
Mulungu adampatsa gawo lakelake. Koma ngati munthu ukufuna kupereka
chilawo (wasiya) pachuma chako, pereka wasiyawo iwe usanafe. Ndipo gawo
lawasiyawo lisapyole pa 73.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
68
Y *>l
T SyLJl 3jj-*»
mpaka Tsiku lomaliza. Ndipo iwo
ndi Anthu akumoto. M'menemo
adzakhalamo mpaka muyaya. 1
218. Ndithudi, amene
akhulupirira, Ndi amene asamuka
namenyana Pa njira ya Mulungu,
iwo ndi amene akuyembekezera
Chifundo cha Mulungu. Ndipo
Mulungu Ngokhululuka kwambiri,
Ngwachisoni chochuluka.
219. Akukufunsa zamowa ndi
njuga. Nena: M'zimenezo muli
masautso ndi uchimo waukulu, ndi
zina zothandiza kwa anthu. Koma
masautso ake ngakulu zedi kuposa
zothandiza zake. Ndipo
akukufunsa kuti aperekenji: Auze:
"chimene chapyolerapo (Pazofuna
zanu)". Umo ndi momwe Mulungu
akukufotokozerani ma Aya
(malamulo) kuti mulingalire.
220. (Kuti muganizire zinthu)
zam'dziko lapansi ndi (zinthu) za
tsiku lomaliza. Ndipo akukufunsa
QlxSKxi*
'- &&z
1 Omtsatira a Mneneri (maswahaba) anakumana ndi osakhulupirira padeti ya
30, m'mwezi wa 9 pakalendala ya Chisilamu. Ena amaganiza kuti detilo la pa
30 lidali la m'mwezi wa Rajabu omwe ngoletsedwa kuchitamo nkhondo.
Tero Akuraishi adamnamizira Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale
naye) kuti waswa ulemerero wamiyezi yopatulika. Ndipo adabwera
kukamfunsa kuti: "Kodi ndimmene ukuchitira?" Umo ndi momwe Mulungu
adawayankhira.
2 Apa akufotokoza kuti masautso ndi mavuto omwe mowa ndi njuga
zimadzetsa ngakulu zedi kuposa ubwino wake. Mowa umamchotsa munthu
nzeru pomwe nzeru ndidalitso lalikulu kuposa chilichonse. Ndipo mowa
umamuonongera munthu chuma ndi kumdzetsera matenda m'thupi mwake.
Nayonso njuga nchimodzimodzi. Imawononga chuma ndi kuyambitsa chidani
pakati pa anthu. Zonsezi zimadzetsa chisokonezo kumtundu wa munthu.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
69
t *>»
t SyUi 5j^»
za ana a masiye, Nena:
"Kuwachitira zabwino ndiwo
ubwino; ngati mutasakanikirana
nawo, (ndibwinonso). Iwo ndi
abale anu; ndipo Mulungu
akumdziwa woononga ndi wochita
zabwino. Ndipo Mulungu
akadafuna, akadakukhwimitsirani
malamulo. Ndithudi, Mulungu
Ngwamphamvu zoposa;
Ngwanzeru zakuya.
221. Ndipo musakwatire akazi
opembedza Mafano Mpaka
atakhulupirira. Ndithudi,
mdzakazi Wokhulupirira
(Mulungu) ngwabwino kuposa
Mfulu yachikazi yosakhulupirira,
Ngakhale itakukondweretsani.
(Ndipo ana anu aakazi a
Chisilamu) Musawakwatitse kwa
amuna Osakhulupirira, mpaka
akhulupirire. Ndipo kapolo
wokhulupirira (Mulungu)
Ngwabwino kuposa mfulu
yosakhulupirira, Ngakhale
ikukukondweretsani. I wo wo
akuitanira kumoto. Koma Mulungu
akuitanira kumunda Wamtendere
ndi kuchikhululuko Mwalamulo
lake. Ndipo lye akulongosola
Mwatsatanetsatane ndime za
mawu ake Kwa anthu, kuti athe
kukumbukira. l
Ndime iyi ikuletsa Asilamu kukwatirana ndi anthu osakhulupirira Mulungu
kupatula Akhirisitu ndi Ayuda. Nkosaloledwa mwamuna wa Chisilamu
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
70
Y ^>l
Y SjiJl 5jj-*»
222. Ndipo (iwo) akukufunsa za
Kukhala malo amodzi ndi Azimayi
panthawi imene Akusamba, auze
(kuti): "Zimenezo ndizovulaza
(Ndiponso ndiuve). Choncho
Apatukireni akazi m'nthawi
Yamatenda akumwezi, Ndipo
musawayandikire mpaka ayere.
Ngati atayera, kumananaoni
Kupyolera m'njira yomwe
Mulungu Wakulamulani. Ndithu,
Mulungu Amakonda olapa,
ndiponso Amakonda odziyeretsa.
223. Akazi anu ali ngati minda
yanu; Choncho idzereni minda
yanu Mmene mungafunire; Koma
dzitsogozereni zabwino Nokha,
ndipo opani Mulungu, Ndipo
dziwaninso kuti Mudzakumana
naye. Ndipo auze nkhani Yabwino
amene akhulupirira
224. Ndipo kulumbirira kwanu
Dzina la Mulungu musakuchite
Kukhala chokuletsani Kuchita
zinthu zabwino (Zam'Chisilamu)
ndi kuopa Mulungu, ndi
kuyanjanitsa Pakati pa anthu.
Ndipo Mulungu Ngwakumva,
Ngodziwa. 1
kukwatira mkazi wopembedza mafano. Nkosaloledwa kuti mkazi wa
Chisilamu akwatiwe ndi mwamuna wopembedza mafano. Koma mwamuna
wa Chisilamu atha kukwatira mkazi wa Chikhrisitu kapena wa Chiyuda pomwe
mkazi wa Chisilamu saloledwa kukwatiwa ndi mwamuna wa Chikhrisitu
kapena wa Chiyuda.
1 Munthu ngati atalumbira kuti sachita chakutichakuti monga kunena kuti,
"ndikulumbira Mulungu sindidzakhudzana naye uje", asasiye kukamba naye
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
71
1 *»>l
Y 5^iJl 9jj~t
225. Mulungu sangakulangeni
Pakulumbira kwanu kopanda Pake,
koma adzakulangani Chifukwa cha
malumbiro Anu amene mitima
Yanu yatsimikiza Mwamphamvu.
Ndipo Mulungu Ngokhululuka
Kwabasi, Ndiponso Woleza.
226. Kwa omwe akulumbirira
Kuti adzipatula kwa akazi awo,
(Nyengo yawo) ayembekezere
Miyezi inayi. Koma ngati
Atabwerera (Nakhala pamodzi Ndi
akazi awo), ndithudi Mulungu
Ngokhululuka kwambiri,
Ndiponso Ngwachisoni zedi. 1
227. Ndipo ngati atatsimikiza
Kulekana, Ndithudi Mulungu
Ngwakumva, Ngodziwa.
228. Ndipo akazi osiidwa
(asakwatiwe) Ayembekezere
mpaka kuyeretsedwa Kutatu
kukwanire. Ndipo nkosafunika
Kwaiwo kubisa chimene Mulungu
walenga m'mimba zawo, ngati
Akukhulupiriradi Mulungu ndi
tsiku Lomaliza. Ndipo amuna awo
Ali ndi udindo wowayenereza
munthuyo chifukwa chakuti adalumbirira kusayankhulana naye. Koma
ayankhulane naye pambuyo popereka dipo kwa masikini pazomwe
adalumbirazo.
1 Mwamuna akalumbira kuti sakhala naye pamodzi mkazi wake, tero mkaziyo
ayembekezere nthawi yamiyezi inayi. Ndipo ngati nthawiyi ipambana
asanakhalebe naye pamodzi, apite akamsumire kwa Kadhwi (mkulu wodziwa
malamulo a Chisilamu). Ndipo Kadhwiyo akakamize mwamunayo kuti akhale
naye pamodzi mkazi wakeyo, apo ayi, awalekanitse ngati izo zitalephereka.
Sibwino kuvutitsana pakati pa anthu makamaka pakati pamwamuna ndi mkazi.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2 | 72 | T »>i
Y SyiJt 5jj-*»
Kuwabwerera m' nthawi yomweyo *-££ &\y\S-j* &*d&$o£&
ngati akufuna Kuchita chimvano. ' ~ $ 9 <"
Nawonso azimayi ali ndi Zofunika ^V*
kuchitiridwa (ndi amuna awo)
monga M'mene ziliri kwa
azimayiwo kuchitira amuna Awo
mwachilamulo cha Shariya. Koma
amuna ali ndi udindo okulirapo
Kuposa iwo. Ndipo Mulungu
Ngwamphamvu zoposa;
Ngwanzeru zakuya. 1
1 Mkazi ngati amsudzula ukwati saloledwa kukwatiwa ndi mwamuna wina
mpaka eda yake ithe. Ndipo eda njosiyanasiyana kwa akazi. Edayi njotere
kusiyana kwake:
1. Mkazi akasiyidwa ali ndi mimba, pamenepo ndiye kuti eda yake imatha
akangobereka. Pompo mwamuna wina akhoza kumkwatira.
2. Ngati wosiidwayo ndi mkazi yemwe sadwala matenda akumwezi
(a) chifukwa chakukalamba
(b) kapena chifukwa chakuti sanakwane zaka zoyambira kudwala kumweziko
(c) kapena chifukwa chakuti chilengedwe chake chili momwemo
(d) kapena zifukwa zina zomwe zimachititsa kuti asadwale matenda
akumwezi eda yawo onsewa ndimiyezi itatu. Asakwatiwe mpaka miyezi itatu
ithe kuchokera patsiku lomwe adawasudzula.
3. Ngati wosudzulidwayo ndimkazi wodwala matenda akumwezi, eda yake
imatha akamaliza "khului" zitatu. Tsono tanthauzo lakhului maulama
amamasulira mosiyanasiyana. Pamazihabi a Imam Shafii tanthauzo lake
ndikuyeretsedwa kutatu (twahara zitatu). Choncho kuyeretsedwa kutatuku
kukatha kuyambira pomwe adamsudzula, akhoza kukwatiwa. Koma
pamazihabi a Kibazi tanthauzo lake ndikudwala kumwezi katatu (hizi zitatu).
Kukatha kudwala kumwezi kutatu komwe kwachitika pambuyo pamsudzulo
ndiye kuti akhoza kukwatiwa. Eda ngati siinathe mkazi saloledwa kukwatiwa.
Ngati atakwatiwa ali mu eda ukwatiwo suvomerezeka. Ndiye kutinso nthawi
yonse yomwe mkaziyo akukhala limodzi ndi mwamunayo akuchita naye
chiwerewere. Ndipo amene akubadwa mu ukwati wotere ndi ana obadwira mu
chiwerewere. Akazi omwe asiidwa ukwati akuwalangiza kuti asabise mimba
kuti mwanayo adzadziwike tate wake. Ngati eda siinathe ndiponso ngati
kuchuluka kwa twalaka mwamuna sadamalize, mwamunayo ali ndi ufulu
wobwererana ndi mkazi ngati atafuna. Tero padzangofunika kupeza mboni
ziwiri zoti zimdziwitse mkaziyo kuti wamuna wake wabwererana naye.
Mkaziyo kapenanso abale ake saloledwa kukaniza zimenezo.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
73
t *jA-i
t 5^aJ| 5jj-*»
229. Mawu achilekaniro
chaukwati (twalaka) (Omwe
akupereka mwayi kwa mwamuna
Kubwereranso kwa mkazi wake),
ndiomwe Anenedwa kawiri.
Kenako amkhazike (Mkaziyo)
mwaubwino (ngati afuna
kubwererana Naye) kapena
alekane mwaubwino (ngati
Atafunadi kumleka. Ndipo
sangathe kubwererana Naye ngati
atamunenera kachitatu mawu
Achilekano pokhapokha
atakwatiwapo poyamba Ndi
mwamuna ndi kusiidwa ndi
mwamunayo). Ndipo sizili
zololedwa Kwa inu kuti mutenge
(kulanda) chilichonse Chimene
mudawapatsa (akazi anu)
pokhapokha (Onse awiri) ngati
akuopa kuti satha Kusunga malire
a Mulungu (malamulo a Mulungu).
Ngati muopa kuti sasunga malire
A Mulungu, ndiye kuti pamenepo
pakhala Popanda tchimo kwa iwo
(mwamuna woyamba Ndi
mkaziyu) kulandira (kapena
kupereka) Chodziombolera mkazi.
Awa ndiwo malire a Mulungu;
choncho musawalumphe. Ndipo
amene Alumphe malire a Mulungu
(powaswa), iwowo Ndiwo anthu
ochitazoipa. 1
Apa akuletsa kumlanda kanthu mkazi kapena kumuuza kuti abweze
(mahari) chiwongo akalangidwe nawo patsiku lachimaliziro. Pamalo pamodzi
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
74
t *>»
t SyLJl 3jj-*
230. Tero ngati atamuleka (ndi
Kunena katatu mawu achilekaniro,
Choncho mkazi ameneyo)
ngosaloledwa kwa iye pambuyo
Pakutero, kufikira akwatiwe ndi
Mwamuna wina. (Ngati mwamuna
Winayo atamusiya), palibe
Kulakwa kwa awiriwo
kubwererana Ngati akuona kuti
adzasunga Malire a Mulungu.
Ndipo awa ndi Malire a Mulungu
omwe Akuwalongosola kwa anthu
odziwa.
231. Ndipo pamene musiya
akazi Powanenera mawu
achilekaniro, Niiyandikira
kukwana nyengo
yachiyembekezero Chawo (eda
yawo), abwerereni Mwaubwino;
kapena lekananaoni mwaubwino,
ndipo musawabwerere
Mowavutitsa kuti mupyole malire
A Mulungu (poswa malamulo
ake). Ndipo amene achite
zimenezo ndiye kuti wadzichitira
yekha zoipa. Ndipo ndime za
mawu a Mulungu Musazichitire
chibwana. Ndipo Kumbukirani
mtendere wa Mulungu umene uli
pa inu; Makamaka chisomo
Chokuvumbulutsirani Buku (La
Qur'an) ndi kudziwitsidwa Nzeru
zomwe akukulangizani nazo.
pokha mpomwe pali povomerezeka mkazi kudziombola kwa mwamuna wake
ngati mkaziyo njemwe wafuna kuti ukwatiwo uthe, ndiponso ngati palibe
choipa chilichonse chomwe mwamunayo akuchita ndipo sangathe kukhala
naye mwamtendere. Pamenepa ndiye kuti mkaziyo abweze chiwongo kuti
adzichotsemo muukwati woterowo.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
75
Y ^jA-i
t S^iJt 5jj-*>
Ndipo opani Mulungu, Ndithudi
dziwani kuti Mulungu Ngodziwa
chirichonse. 1
232. Ndipo akazi mukawanenera
Mawu achilekaniro (Oyamba Ndi
achiwiri), iwo nakwaniritsa
Chiyembekezero chawo, choncho
(Inu abale Amkazi), musawaletse
Kukwatiwanso ndi amuna awo
(Kubwererana) ngati pali
chimvano Pakati pawo
mwaubwino. Zimenezo
Akulangizidwa nazo mwainu
yemwe Akukhulupirira Mulungu
Ndi tsiku lomaliza. Zimenezo
nzabwino Kwa inu, ndiponso
zoyeretsa. Ndipo Mulungu
akudziwa, pomwe Inu simudziwa.
233. Ndipo akazi omwe
angobereka kumene Ayamwitse
ana awo zaka ziwiri zathunthu
Kwa yemwe akufuna kukwaniritsa
kuyamwitsa. Ndi udindo wa
abambo kuwapezera chakudya
Chawo anawo ndi amayiwo,
ndiponso Kuwapezera chovala
chawo anawo ndi amayiwo,
Motsatira malamulo a Shariya.
Ndipo mzimu wa Munthu aliyense
sukakamizidwa, koma m'mene
Ungathere. Ndipo mayi
wamwanayo asazunzidwe
9' . \1'99 ^ul.j, 999* 9 \X
1 Apa amuna akuwalangiza kuti awabwerere akazi awo mwachangu nthawi ya
eda isanathe kuopa kuti ikatha ndiye kuti akwatiwa ndi amuna ena. Komatu
akuwalangiza kuti abwererane nawo akaziwo ncholinga chokhala nawo
mwaubwino, osati kubwererana nawo ncholinga chowavutitsa.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
76
Y *>l
Y SyM' ^J-**
Chifukwa chamwana wakeyo.
Nayenso bambo Wamwanayo
asazunzike chifukwa chamwana
Wakeyo. Ndipo lamuloli lilinso
chimodzimodzi Pa mlowam'malo
(ngati bambo atamwalira). Ndipo
onse awiri ngati atafuna kumletsa
Kuyamwa, mogwirizana Pakati pa
awiriwo, ndimokambirana palibe
Kulakwa pa iwo awiriwo. Ndipo
Ngati mutafuna kuwapezera ana
anu akazi Ena owayamwitsa
(omwe si amayi awo), palibe
Uchimo mwa inu ngati mwapereka
chimene Mudalonjeza kuwapatsa
(oyamwitsawo) Mwaubwino.
Ndipo opani Mulungu;
Dziwaninso kuti Mulungu akuona
Zonse zimene mukuchita. 1
234. Ndipo mwainu amene
amwalira Nasiya akazi, choncho
£$^^j&£a;
^^i^^^lii^^ba^
1 Mwana amayamwitsidwa ndi mayi wake m'nthawi yazaka ziwiri. Ndipo
akhoza kupitiriza kumuyamwitsa zitapita zaka ziwiri. Sikoletsedwa, koma
sibwino. Ndipo mayiyo akhoza ngati atagwirizana ndi tate wamwanayo
kumsiitsa zaka ziwiri zisanakwane ngati ali ndichitsimikizo choti mwanayo
sapeza masautso. Ndipo tate ngati adalekana naye ukwati mayi wamwanayo
pomwe mayiyo akupitiriza kuyamwitsa mwanayo, nkofunika kwa tate
wamwanayo kupereka malipiro kwa mayi wamwanayo, monga kumpezera
chakudya chake mayiyo ndi zovala zake ndi ndalama zolipirira pamalo
pokhala ndi zina zotere.
Mwamuna asanene kwa mkaziyo kuti "Uyu mwana wako. Tero uwona
chochita naye." Pamenepo mpovuta chifukwa mkaziyo sangapeze munthu
womthandiza iye ndi mwanayo.
Makamaka izi zingachitike ngati mkaziyo sanakwatiwe ndi mwamuna wina.
Nayenso mayi wamwanayo asamkhwimitsire mwamunayo malipiro operekedwawo.
Koma zonse zikhale zaubwino.
Ngati tate wamwanayo palibe, ndiye kuti mlowam'malo wa tateyo ndiye
adzakwaniritse zimenezo.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
77
1 T»>i
T S^aJi 5jj-*»
(akaziwo) Ayembekezere
(asakwatiwe) Miyezi inayi ndi
masiku khumi. Ndipo akakwanitsa
nyengo Ya chiyembekezero chawo
cha Eda, sitchimo kwa inu
Pazimene akaziwo adzichitira
Okha (monga kudzikongoletsa Ndi
kudziwonetsa kwa ofunsira
Ukwati); komabe zikhale motsatira
Mmalamulo a Shariya. Ndipo
Mulungu Ngodziwa zonse zimene
mukuchita.
235. Ndipo sitchimo kwa inu
kupereka mawu Okuluwika
ofunsira ukwati kwa akaziwo
(Pamene chiyembekezero cha eda
yawo Chisanathe. Ndiponso palibe
uchimo) Kapena kubisa mumtima
mwanu, Kuwakwatira
(Chiyembekezo chawo
Chikadzatha). Mulungu wadziwa
kuti Mukhala mukuwakumbukira
akaziwo. Koma Musawalonjeze
mobisa (kuti: "Ikatha eda
Ndidzakukwatira.)" Koma nenani
mawu Abwino. Ndipo
musatsimikize kumanga ukwati
Mpaka nyengo yolembedwayo
ikwanire. Ndipo Dziwani kuti
Mulungu akudziwa zomwe zili
M'mitima mwanu. Tero
chenjeranayeni (Mulungu),
dziwaninso kuti Mulungu
Ngokhululuka kwabasi, Ngoleza.
236. Palibe tchimo pa inu
mutawapatsa Akazi mawu
£vty$&a$&'7&$
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
78
Y *>i
Y 5jiJl 5jj-»
achilekaniro pomwe
Simudakhudzane nawo; pomwenso
Simudawadziwitse gawo la
chiwongo Chawo (mahari yawo);
Koma asangalatseni powapatsa
chilekaniro. Opeza bwino apereke
malinga ndikupeza Bwino kwake;
wochepekedwa apereke Malingana
ndikuchepekedwa kwake.
Chilekaniro chosangalatsacho
chikhale Molingana ndi Malamulo
a Shariya, Ndipo ndilamulo kwa
Ochita zabwino. 1
237. Ndipo ngati mwalekana
nawo (akaziwo) Musanakhudzane
nawo mutawadziwitsa Gawo
lachiwongo chawo, apatseni Theka
lachimene mudagwirizana
Kuwapatsa pokhapokha ngati
akaziwo atakana Okha (theka la
chiwongocho), kapena
(Mwamuna) uja yemwe
kumangitsa kwaukwati Kuli
m'manja mwake amusiire
(chiwongo Chonsecho mkaziyo).
1 Kuthetsa ukwati nkololedwa m'Chisilamu. Koma ngakhale nkololedwa
Shariya ya Chisilamu imanyansidwa ndimachitidwe othetsa ukwati
pokhapokha pakhale zifukwa zovomerezeka ndi Shariya.
Ngati patapezeka zifukwa zochititsa kuti ukwati uthe nkofunika kuti mkwati
amchitire mkwatibwi zabwino monga izi:
a) ampatse chiwongo (mahali) chimene chinatsalira ngati sadamalize
kupereka.
b) ampatse ndalama zina zapadera zomtulutsira mkaziyo m'nyumba.
c) ampatse chovala, malo okhala, chakudya patsiku lililonse kufikira eda yake
itatha ngakhale edayo itatenga nthawi yaitali.
d) amsiire zinthu zake kuti atenge pamodzi ndi zimene adampatsa.
Nkosaloledwa kumlanda chilichonse mwazimenezi.
Surat 2. AI-Baqarah Juzu 2 79 T *j*-i
t S^flJl 3jj-a
Ndipo ngati mutasiirana
(Zimenezo) zingakuyandikitseni
kumbali Yoopa Mulungu. Ndipo
musaiwale kuchitirana Zabwino
pakati panu (ngakhale kuti
Mukulekana). Ndithudi Mulungu
akuona zonse Zimene mukuchita. 1
238. Sungani mokwanira Swala
Makamaka Swala Yapakatikati;
ndipo Imirirani modzichepetsa
kwa Mulungu. 2
1 Ngati udamkwatira mkazi ndipo nkulekana naye usanalowane naye,
umpatse theka lachiwongo chomwe chidatchuiidwa. Ngati udampatsa
chiwongo chonse, ndiye kuti akubwezere theka lake. Koma ndibwino kwa
mwamuna kumpatsa mkazi chiwongo chonse ngati anali asanampatse. Ngati
anampatsa asaitanitsenso chiwongocho. Ndibwinonso kwa mkazi kubweza
chiwongo chonse ngati adampatsa chonse, kapena kukana kuti asampatse
ngati anali asanapatsidwe. Aliyense mwa awiriwa asakhale ndi chibaba
chofuna kupeza ndalama pakutha pa ukwatiwo. Malamulo tanenawa
amagwira ntchito ngati chiwongo chidatchuiidwa kuchuluka kwake pomwe
ankafunsira ukwati. Koma ngati chiwongocho sanachitchule kuchuluka kwake
kotero kuti sadagwirizane za chiwongocho kuti adzapereka mwakutimwakuti,
pamenepa ndiye kuti ampatse chinthu cholekanira choti chimsangalatse. Hi
ndilo tanthauzo lazomwe zatchulidwa m'ndime ya 236.
Ndithudi apa akutilangiza mwamphamvu kuti tizichitirana zabwino ngakhale
panthawi yolekana ukwati. Anthu asaiwale ubwino ndi chikondi zomwe
ankachitirana pakati pawo.
2 M'ndime iyi akulimbikitsa kuti Swala zonse anthu azipemphere muunyinji
wawo osati munthu payekhapayekha makamaka Swala yapakatikati. Ena
mwa maulama adati Swala yapakatikati ndiswala ya Azuhuri.
Imapempheredwa pakatikati pamasana, dzuwa litatentha kwambiri monga
momwe zilili m'maiko a Arabu.
Paswala ya Azuhuri anthu amavutika kwambiri kukapemphera m'misikiti
chifukwa chakutentha kwa dzuwa. Choncho apa akuwalimbikitsa kuti
azikapemphera m'misikiti ngakhale kuli kotentha. Pomwe ena akuti Swala
yapakatikati ndi Swala ya Fajiri (Subuhi) imene imapempheredwa pakatikati
panthawi. Simasana ndiponso siusiku. Apa mpanthawi pomwe tulo timakhala
tamphamvu. Tero akuwalimbikitsa anthu kusiya tuloto nkupita kumisikiti
nkukapemphera Swala ya (jama) yapagulu. Ndipo akutilimbikitsanso kuti
tizipemphera mofatsira ndi modzichepetsa. Ndikuti tikamapemphera tizidziwa
kuti taimirira pamaso pa Mulungu.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
80
r *>i
T 0jiaJ\ 0jj~*
239. Ndipo ngati muli ndi
mantha (kupemphera Mwalamulo
pamene mukumenyana Ndi adani
anu), pempherani uku Mukuyenda,
kapena mutakwera Chokwera.
Ndipo mukakhala Pachitetezo
mkumbukireni Mulungu
(Pempherani) monga momwe
Wakuphunzitsirani Zomwe
simudali kuzidziwa.
240. Ndipo mwainu amene
amwalira nasiya akazi
Awo,alangize (amlowam'malo
awo) za akazi awo Kuti awapatse
zodyera m'nyengo yachaka
Chimodzi popanda kutulutsidwa
(m'nyumba Zomwe ankakhala ndi
amuna awo). Koma Ngati akazi wo
atuluka (okha), palibe Kulakwa
painu pazimene adzichitira okha
Zomwe nzogwirizana ndi
chilamulo cha Shariya. Ndipo
Mulungu Ngwamphamvu Zoposa;
Ngwanzeru zakuya.
241. Ndipo akazi osiidwa
ukwati, apatsidwe chilekaniro
Chowasangalatsa m' chilamulo Cha
Shariya. Hi ndi lamulo Kwa amene
akuopa Mulungu. l
242. Umu ndi momwe Mulungu
Akukulongosolerani Ma aya
' 99<*<.
Pamene mwamuna akumsiya mkazi ukwati pafunika kuti ampatse chinthu
china kuwonjezera pa chiwongo. Koma Asilamu ambiri kudera la kuno
kum'mawa kwa Afrika m'malo mompatsa chinthu mkazi pomusiya amaitanitsa
chinthu kwamkazi kuti awapatse kapena kumlanda katundu kumene.
Machitidwe otere ngoipitsitsa, sali ogwirizana ndi malamulo a Chisilamu.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
81
r *>»
Y SyJ* ojj-»
(ndime) Ake Kuti inu mukhale
Ndinzeru.
243. Kodi sudamve (nkhani za)
amene adatuluka M'nyumba zawo
ali zikwizikwi kuopa Imfa? Ndipo
Mulungu adawauza: "Mwalirani",
(ndipo adamwalira chabe Popanda
chifukwa chilichonse). Kenako
Adawaukitsa (kuti adziwe kuti
imfa Njosathawika). Ndithudi,
Mulungu Ndimwini kuchita
zabwino pa anthu, koma Anthu
ambiri sathokoza. l
244. Ndipo menyani nkhondo
panjira Ya Mulungu, ndipo
dziwani Kuti Mulungu
Ngwakumva, Ngodziwa
chilichonse.
245. Kodi ndani angamkongoze
Mulungu Ngongole ya bwino
(yochokera m'chuma Chake
powapatsa amphawi ndi kupereka
Pa njira ya Mulungu) kuti
amuonjezere Zoonjezera zambiri?
Ndipo Mulungu Ndi Yemwe
amafumbata ndi Kutambasula,
ndipo kwa lye Nkumene
mudzabwezedwa. 2
W&^^'dMl
1 Ibun Abbas adati anthuwo adali zikwi zinayi. Adatuluka m'nyumba zawo
kuthawa mliri wanthomba, nati pakati pawo: "Tipite kudziko lina komwe kulibe
imfa yanthomba." Choncho adayenda mpaka kufika pamalo pena; ndipo
Mulungu adati kwa iwo: "Mwalirani," ndipo onse anamwaliradi nthawi
yomweyo. Ndipo mmodzi wa aneneri adawadutsa iwo ali akufa, nampempha
Mbuye wake kuti awawukitse kuti azimgwadira. Choncho adawaukitsa.
Nkhaniyi tikuphunziramo zoti imfa siithawika.
2 Apa anthu akuwalimbikitsa kuti azipereka chuma chawo panjira zabwino
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
82
T frjJt-1
T SjiJl 5jj-a
246. Kodi sudamve nkhani ya
akuluakulu Aana a Israyeli
pambuyo pa Musa? Adanena kwa
mneneri wawo: "Tidzozere mfumu
kuti timenye Nkhondo pa njira ya
Mulungu." lye (Mneneri wawoyo)
Adati: "Mwinatu simungamenye
Nkhondoyo ngati kutalamulidwa
kwa inu. (Iwo) adati: "Nchotani
kuti tisamenye Nkhondo panjira ya
Mulungu pomwe Tatulutsidwa
m'nyumba zathu pamodzi ndi Ana
athu?" Koma pamene
adalamulidwa Kumenya
nkhondoyo, adatembenuka,
Kupatula ochepa mwaiwo. Ndipo
Mulungu akudziwa Bwinobwino
za anthu ochita zoipa.
247. Ndipo Mneneri wawoyo
adawauza: "Mulungu
Wakusankhirani Taluti kukhala
mfumu. (Iwo ) Adati: "Nchotani
kuti iye akhale ndi ufumu Kuposa
ife pomwe ife ngoyenera kupeza
ufumu Kuposa iye, ndipo
sadapatsidwe chuma Chambiri?"
(Iye) adati: "Mulungu
wamusankha Mwainu, ndipo
wamuonjezera kukhala ndi Nzeru
zopambana ndi kukhala ndi thupi
(Lamphamvu). Ndipo Mulungu
amampatsa Ufumu wake amene
wamfuna. Ndipo Mulungu ndi
ndipo Mulungu adzawalipira mphoto yambiri. Asachite umbombo kupereka
chuma chawo m'njira zabwino pakuti sadaka siichepetsa chuma koma
kuchichulukitsa.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
83
y *>»
T SjiJl 5j^i»
Mwini zopereka zambiri, ndiponso
Ngodziwa."
248, Ndipo Mneneri wawo
adawauza (kuti): "Chizindikiro
chaufumu wake, Ndikukudzerani
Bokosi lomwe mkati mwake Muli
mpumulo wamiyoyo yanu
wochokera Kwa Mbuye wanu, ndi
zotsalira zomwe Adazisiya anthu a
Musa ndi anthu a Haruna,
Atalisenza Angelo. Ndithu,
m'zimenezo muli Chisonyezo
kwainu (chosonyeza kuyenera
Kwa ufumu wake painu) ngati
mulidi Okhulupirira."
249. Choncho, Taluti pamene
adapita ndi Magulu ake a nkhondo,
adati: "Mulungu Akuyesani
mayeso ndi mtsinje (womwe
Mukumane nawo panjira komwe
mukupitako). Choncho amene
akamwe mmenemo sali nane.
Koma amene sakamwa adzakhala
pamodzi Nane kupatula amene
watunga ndi dzanja lake
(Ndikumwa; iyeyo ndiye kuti
Sadalakwe). Koma (iwo) adamwa
m'menemo Kupatula ochepa
mwaiwo. Pamene adaoloka lye
pamodzi ndi aja omwe
adakhulupirira Limodzi naye,
(Iwo) adati: "Lero Sitingamuthe
Jaluti ndi magulu ake ankhondo."
Ndipo omwe adali ndi chitsimikizo
chokumana Ndi Mulungu adati:
"Kodi ndimagulu angati Ochepa
%
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 2
84
r *>i
T S^aJi 5jj-*
amene adagonjetsa magulu ambiri
Mwachilolezo cha Mulungu!
Ndipo Mulungu Ali pamodzi ndi
opirira. 1
250. Ndipo pamene adapita
kukalimbana ndi Jaluti (mfumu ya
adaniwo), pamodzi ndimagulu ake
ankhondo (Anthu a Taluti) adati:
"O! Mbuyewathu! Titsanulireni
chipiriro, ndipo limbikitsani
Mapazi athu; Tithangateni kwa
Anthu osakhulupirira."
251. Choncho, adawagonjetsa
Mwachilolezo cha Mulungu.
Ndipo Daud adapha Jaluti; Ndipo
Mulungu adampatsa Ufumu ndi
uneneri, namphunzitsanso Zimene
adafuna. Mulungu akadapanda
Kukankha anthu ena kupyolera
Mwa anthu ena ndiye kuti dziko
Likadaonongeka. Koma Mulungu
Ndimwini kuchita zabwino
Pazolengedwa zonse.
252. Awa ndi ma aya (ndime) A
Mulungu; tikuwawerenga kwa iwe
(Mtumiki) Mwachoonadi. Ndithudi,
iwe ndi we mmodzi mwa atumiki.
1 Kumvera ndichinthu chachikulu kwabasi kuti zinthu za anthu ziyende bwino.
Anthu osamvera zinthu zawo siziyenda bwino. Ndipo apa mfumuyi ikuchoka
kupita kunkhondo pamodzi ndi gulu lalikulu lankhondo lomwe lidali losamvera.
Choncho Mulungu adaiuza mfumu ija kuti iwayese mayeso oti asamwe madzi
othetsa ludzu lonse. Amene samvera asawatenge kunka nawo kubwalo
lankhondo poona kuti angayambitse chisokonezo kumeneko.
2 Mneneri Daud adali msirikali m'gulu lankhondo lamfumu Taluti. lye
adamenya nkhondo ndi cholinga chabwino ndi mwaungwazi zedi mpaka
adaipha mfumu ya adaniwo yomwe inkatchedwa Jaluti. Tsono Mulungu
adampatsa ufumu chifukwa chakudzipereka kwakeko.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 3
85
r *ji-i
t O^flJl Ojj^t
253. Amenewo ndi aneneri
tidawapatsa ulemerero Mosiyanitsa
pakati pawo, ena kuposa ena. Mwa
iwo alipo amene Mulungu
adawalankhula; Ndipo ena
adawakwezera kwambiri
maulemerero Awo. Naye Yesu
mwana wa Maria tidampatsa
zisonyezo zooneka, ndi
kumlimbikitsa ndi Mzimu Woyera
(mngelo Gabriel). Mulungu
akadafuna Sakadamenyana amene
adalipo pambuyo pawo, (Pa
atumikiwo) pambuyo powadzera
Zizindikiro zooneka. Koma
adasiyana. Choncho mwaiwo alipo
amene adakhulupirira, Ndipo ena
mwaiwo sadakhulupirire. Ndipo
Mulungu akadafuna,
Sakadamenyana; koma Mulungu
Amachita zimene akufuna. ]
254. E inu amene
mwakhulupirira! Perekani mwa
zimene takupatsani Lisanadze
<£tfia«ag63ii<2&
©43$*
1 Ndime iyi ikusonyeza kuti Atumiki maulemerero awo ngosiyanasiyana kwa
Mulungu monga momwenso alili anthu ndi Angelo ndi zinthu zinanso.
Amaposana pakalandiridwe kaulemerero wawo kwa Mulungu chifukwa
chakusiyana zochita zawo. Zochita za ena nzazikulu zedi kapena zochuluka
kwambiri kuposa zochita za anzawo. Ndipo apa Mulungu watchulapo atatu
mwa atumiki akuluakulu omwe ndi:-
(a) Musa amene Mulungu adayankhula naye ndi kumpatsa zozizwitsa
zoonekera.
(b) Ndi mneneri Isa (Yesu) yemwe adampatsa ulemerero waukulu
(c) ndi mneneri Muhammad (SAW).
Enanso mwa Aneneri akuluakulu pali Mneneri Ibrahim ndi Mneneri Nuhi
monga momwe ikufotokozera ndime ya chisanu ndi ziwiri (7) yam'surati
Ahzabi.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 3
86
r *>»
t djiJl djj--
tsiku lomwe Lilibe kugula
(chilichonse Chokupulumutsani)
ngakhale Ubwenzi ngakhalenso
chiombolo. Ndipo osakhulupirira
Ndiwo anthu oipa.
255. Mulungu palibe
wopembedzedwa wina koma lye,
Wamoyo Wamuyaya, Woimira ndi
Woteteza chilichonse. Kusinza
sikumgwira ngakhale tulo. Zonse
zakumwamba ndi zapansi nza lye.
Kodi ndani angathe kuombola
Kwa lye popanda chilolezo
Chake? Akudziwa zapatsogolo ndi
zomwe zili pambuyo pawo ndipo
zolengedwazo sizidziwa
Chilichonse pa zomwe zili
M'kudziwa Kwake kupatula
chimene wafuna. Mpando wake
wakwanira Kumwamba ndi pansi
ndipo Sizimamvuta kuzisunga
zimenezo. Ndipo lye (Yekha)
Njemwe ali
Wapamwambamwamba,
Ngwamkulu kwabasi,
(Ngolemekezeka kwambiri). 1
«^#uJ$!^&$
sui- 1
Ndime iyi ikutchedwa Ayat Kursii; ndime yolemekezeka kwambiri. Kwa
Msilamu aliyense nkofunika kuizindikira bwinobwino ndimeyi kuti azindikire
kuti palibe yemwe angamuike patsogoio kapena pambuyo koma lye Mulungu
wapamwambamwamba. M'hadisi zambiri za Mtumiki akutilimbikitsa
kuiwerenga ndimeyi m'malo awa:-
a) tikatha kuchita salamu paswala iliyonse
b) tisanagone
c) pamene tikutuluka m'nyumba
d) polowa m'nyumba
e) tikadzazidwa ndimantha poopa chinthu chomwe tikuchiona ndi chomwe
sitikuchiona
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 3 87 ? *>*
T 5yiJl 3jj-j
256. Palibe kukakamiza
(munthu kulowa) M'chipembedzo;
kulungama kwaonekera Poyera
kusiyana ndi kusalungama.
Choncho amene akumkana Satana
nakhulupirira Mulungu, ndiye Kuti
wagwira chigwiriro cholimba,
Chomwe sichisweka. Ndipo
Mulungu Ngwakumva;
Ngodziwa.
257. Mulungu ndi mtetezi wa
amene Akhulupirira.
Amawatulutsa kumdima
Ndikuwalowetsa M'kuunika.
Koma amene sadakhulupirire,
Atetezi awo ndi asatana.
Amawatulutsa m'kuunika ndi
kuwalowetsa mumdima Iwo ndi
anthu akumoto. M'menemo
adzakhalamo muyaya.
258. Kodi sudamve zayemwe
adatsutsana ndi Ibrahim pa za
Mbuye wake (Mulungu)?
(Ankanyada) pachifukwa chakuti
Mulungu adampatsa ufumu.
>
Arabu ena a muMzinda wa Madina, Mtumiki (madalitso ndi mtendere
zikhale naye) asanasamukireko adali kutsata chipembedzo cha Chiyuda.
Koma ambiri aiwo adali kupembedza mafano. Pamene chidadza Chisilamu
pafupifupi onse omwe ankapembedza mafano adalowa m' Chisilamu. Koma
amene adali m'chipembedzo cha Chiyuda mpang'ono okha omwe adalowa
m'Chisilamu. Ndipo ena ngakhale anali Arabu adatsalirabe m'chipembedzo
cha Chiyuda. Choncho, atate omwe adali Asilamu pamodzi ndi abale ndi
amuna awo adafuna kukakamiza mwamphamvu amene adali m'chipembedzo
cha Chiyuda kuti alowe m'Chisilamu. Koma Mulungu adawaletsa kuti palibe
kumkakamiza kuti alowe m'Chisilamu yemwe sakufuna. Munthu aliyense
adapatsidwa nzeru yomzindikiritsa chabwino ndi choipa. Ngati afuna kusokera
nkufuna kwake iye mwini. Ndipo Mulungu adzamulanga patsiku Lachimaliziro
osati pano padziko lapansi.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 3
88
r *>i
T Oj^Jl Sjj-j
Ibrahim adati: "Mbuye wanga ndi
Yemwe Amapereka'moyo ndi
imfa." lye adati: "Inenso
ndimapereka moyo ndi imfa."
Ibrahim Adati: "Mulungu
amatulutsa dzuwa kuvuma,
choncho iwe ulitulutse
kuzambwe." Ndipo uja
wosakhulupirira adangoti Kakasi,
(kusowa chonena). Ndipo
Mulungu Satsogolera anthu ochita
zoipa. 1
259. Kapena ngati fanizo la uja
amene adadutsa Pafupi ndi mudzi
umene madenga ndi zipupa zake
zidaphwasuka (udaferatu) adati:
"Kodi Mulungu adzaukitsa chotani
mudzi uwu pambuyo pakufa
kwake?" Ndipo Mulungu
Adampatsa imfa kwanthawi
yokwana zaka Zana limodzi (100),
kenako adamuukitsa Namufunsa:
"Kodi wakhala nyengo yotani?"
M'nthawi ya Mneneri Ibrahim padali mfumu ina yodzikuza yomwe
inkadzitcha kuti ndimulungu ndipo anthu ake adali kuipembedza. Pamene
Mneneri Ibrahim adadza nayamba kuphunzitsa chipembedzo choona ndikuti
iyeyo simulungu, mfumuyo idati kwa Mneneri Ibrahim: "Kodi Mulungu wako
woonayo amachita chiyani?" lye adati "Amapereka moyo ndi kuperekanso
imfa." Mfumuyo idachita ngati sidamvetse cholinga chamawu a Mneneri
Ibrahim. Idati: "Nanenso ndimachita zimenezo. Taona mmene ndimachitira."
Pompo adalamula kuti abwere nawo anthu awiri omwe adawalamula kuti
aphedwe. lye adalamula kuti mmodzi aphedwe ndipo winayo amsiye.
Choncho zidachitika. Tsono adamuuza Ibrahim: "Waona bwanji? Kodi wina
sindidampatse moyo ndipo winayo imfa?" Mneneri Ibrahim pomwe anaona kuti
mfumuyo ikungodzipusitsa daladala adaiuza chinthu chomwe iyo sikadatha
kuchichita. Adati: "Mulungu amatulutsa dzuwa kuvuma ndipo iwe ulitulutse
kuzambwe." Pamenepo mfumuyo idangoti kakasi, sidachite chilichonse
ndiponso sidanene chilichonse.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 3
89
r *>i
X djA-Jl Ojj-rf
Adati: "Ndakhala nthawi yatsiku
limodzi, Kapena theka latsiku."
(Mulungu) adati: "Koma wakhala
zaka zana limodzi, ndipo ona
Chakudya chako ndi zakumwa
zako, sizinaonongeke
(sizinavunde). Ndipo yang'ana
Bulu wako (ali mafupa okhaokha
oyoyoka);ndi Kuti ukhale
chisonyezo kwa Anthu,
(nchifukwa chake takuukitsa ku
imfa). Ndipo yang'ana
mafupa(abulu wako) momwe
Tingawaukitsire, kenako
nkumaaveka Minofu." choncho
pamene zidazindikirika (kwa iye,
woukitsidwayo), adati:
"Ndikudziwa kuti Mulungu
Ngokhoza chilichonse." 1
260. Ndipo (kumbukira) pamene
Ibrahim adati: "E! Mbuye wanga,
ndionetseni mmene
Mudzaaukitsire akufa."
(Mulungu) adati: "Kodi
sunakhulupirirebe?" Adati: "Iyayi,
(Ndikukhulupirira), koma
(ndikufuna kuona Zimenezo) kuti
mtima wanga ukhazikike."
(Mulungu) adati: "Choncho
katenge mbalame Zinayi;
uzisonkhanitse kwa iwe (mpaka
Munthu ameneyu pamodzi ndi anzake panthawiyo sadali ndi chitsimikizo
kuti Mulungu angaukitse munthu wakufa. Ankaganiza kuti nchinthu
chosatheka kuchitika. Choncho Mulungu adamsonyeza zimenezo kupyolera
mwaiye mwini kuti akauze anzake omwenso adali osakhulupirira zakuuka ku
imfa.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 3
90
r *>i
t o^aJi $JJ-»
Uyizindikire mbalame iliyonse
mmene ilili, Ndipo kenako
uziduledule zonsezo
Zidutswazidutswa ndikuzisakaniza
ndi kuzigawa Mzigawo zinayi).
Ndipo paphiri lililonse Ukaikepo
gawo limodzi la zimenezo, ndipo
Kenako uziitane. Zikudzera
zikuthamanga. Ndipo dziwa kuti
Mulungu ndi Mwini mphamvu
Zoposa, Ngwanzeru zakuya." 1
261, Fanizo la amene akupereka
chuma chawo Panjira ya Mulungu
lili ngati fanizo Lanjere imodzi
yomwe yatulutsa ngala Zisanu ndi
ziwiri. Ndipo ngala iliyonse
Nkukhalamo njere zana limodzi.
Ndipo Mulungu amamuonjezera
Amene wamfuna (kuposera
pamenepa). Ndipo Mulungu ali
Nazo zambiri, Ngodziwa.
19 ">\ 99"\\'*'\ '9L m *9'9 *fi\<'
Mneneri Ibrahim adalakalaka kuti aone mmene akufa adzaukira kuti
chikhulupiriro chake chiwonjezeke mphamvu. Tero Mulungu adamulamula kuti
azinge mbalame zinayi zosiyanasiyana mitundu. Kenako azisakanize ziwalo
zake. Ziwalo za mbalame ina zilowe kumbalame ina. Tsono azigawe miyulu
inayi.Mulu uliwonse akauike paphiri lakelake. Kenako aziitane mbalame zija.
Ndipo aona kuti chiwalo chilichonse chikuthamangira kumbalame yake,
pompo zonsezo zikhalanso mbalame zamoyo monga momwe zidalili
poyamba.
(Ndime 261-7) Ndime izi zonse zikulimbikitsa kupereka chuma panjira
zabwino ndiponso zikuonetsa ubwino umene woperekayo amalandira kwa
Mulungu. Komatu woperekayo kuti apeze ubwino wa Mulungu pafunika izi:
(a) apereke chifukwa cha Mulungu osati ncholinga chodzionetsera kwa anthu,
(b) choperekacho chikhale chabwino. Ngati wapereka zomwe sizabwino ndiye
kuti sangapeze mphoto yaikulu,
(c) asawakumbe amene akuwapatsawo.
(d) Asawavutitse. Ndipo ngati atachita zimenezi ndiye kuti sangapeze
mphoto koma kungotaya chuma pachabe. Kumbwezera mawu abwino
wopempha nkopindulitsa kuposa sadaka yotonzera.
(e) Chimene akuperekacho chikhale chaHalali (chololedwa). Osati chomwe
adachipeza m'njira yosavomerezeka.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 3
91
r *>i
Y OjiJl djj^
262. (Anthu) amene akupereka
chuma Chawo panjira ya Mulungu
napanda Kutsatiza pazomwe
aperekazo Kukumba, ndiponso
masautso Iwo ali ndi mphoto kwa
Mbuye Wawo ndipo pa iwo
Sipadzakhala mantha; Ndiponso
sadzadandaula.
263. Mawu abwino, ndi
kukhululukira (Amene
wakulakwira) nzabwino zedi
kuposa sadaka yotsatizidwa Ndi
masautso. Ndipo Mulungu Ndi
Yemwe ali wolemera kwambiri
Ndiponso Woleza
(Kwazolengedwa zake).
264. E inu amene
mwakhulupirira! Musaononge
sadaka zanu pokumba Ndiponso
popereka masautso, Monga yemwe
akupereka chuma chake
Modzionetsera kwa anthu, ndipo
Sakhulupirira Mulungu ndi tsiku
Lomaliza. Choncho fanizo lake lili
ngati Thanthwe lomwe pamwamba
pake pali dothi Kenako nkulifikira
chimvula (nkuchotsa dothi Lonse
lija), nkulisiya lopanda kanthu.
Tero sadzatha kupeza chilichonse
Pazimene adachita. Ndipo
Mulungu satsogolera anthu
osakhulupirira.
265. Ndipo fanizo la anthu
amene akupereka Chuma chawo
chifukwa chofuna chiyanjo cha
r^j&&\<&^Q.$\$&s
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 3
92
r >>i
Y SyM' <>jj->
Mulungu ndi kulimbikitsa mitima
Yawo (pa chipembedzo cha
Mulungu) lili ngati fanizo la
munda umene uli Pachitunda,
chiufikira chimvula tero
Nubweretsa zinthu zake
dzochuluka Moonjeza kawiri
(kuposera pachikhalidwe Chake).
Ndipo ngati chimvula
sichidaudzere, Ndiye kuti
yamawawa (nkuukwanira
mundawo). Ndipo Mulungu
akuona zonse zimene mukuchita.
266. Kodi mmodzi wa inu
angakonde Kukhala ndi munda
wamitengo Yakanjedza ndi
mphesa womwe Pansi pake
mitsinje ikuyenda, iye Mmenemo
napeza dzinthu
dzamitundumitundu, numpeza
ukalamba uku ali ndi ana ofooka;
Ndipo kamvuluvulu wamoto
naugwera (Mundawo), nupsereratu
(Angazikonde Zimenezi)? umo
ndimomwe Mulungu
akukulongosolerani ma aya
(Ndime za mawu ake) kuti
muganizire.
267. E! inu amene
mwakhulupirira! Perekani zabwino
zochokera M' zimene mwapeza ndi
zimene Takutulutsirani m'nthaka,
Ndipo musalinge kupereka Choipa
chomwe inu simukadachilandira
(Ngati akanakupatsani)
J
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 3
93
r *>i
t djiJl 5jj-»
pokhapokha Mochitsinzinira.
(Nanga Mulungu Ndiye alandire
choipacho)? Ndipo dziwani kuti
Mulungu Ngolemera (ndiponso)
Ngotamandidwa.
268. Satana amakuopsezani ndi
umphawi Ndikukulamulirani
kuchita zoipa (Monga umbombo)
pomwe Mulungu akukulonjezani
chikhululuko Kuchokera kwa iye
ndi ubwino (Waukulu ngati
mupereka); ndipo Mulungu ali
nazo Zambiri, Ngodziwa. 1
269. Amapatsa nzeru
(zothandiza) Amene wamfuna;
Ndipo amene wapatsidwa Nzeru,
ndithudi, wapatsidwa Zabwino
® &4*6£&tglg£!fr3
1 (Ndime 268-71) Apa Mulungu akuwalimbikitsa mtima amene akupereka kuti
panthawi iliyonse pamene akupereka Mulungu adzawaonjezera. Ndipo
akuwachenjeza kuti asamamvetsere udyerekezi wa Satana umene amauthira
m'mitima yawo powauza kuti, "Ngati mupereka, musauka." Koma Mulungu
akuwauza kuti, "perekani simusauka. M'malomwake mupeza bwino padziko
lapansi ndi pa tsiku lomaliza."
M'ndime zomwezi Mulungu wafotokoza za (lonjezo) "naziri" kuti naziri iliyonse
imene tikumlonjeza Mulungu akuidziwa.
Mawu oti "Naziri" nga Chiarabu. M'chichewa akuthandauza kuti, "ndikapeza
chakuti ndidzachita chakutichakuti," "kapena kuti, akachira mbale wanga
ndidzapereka chakutichakuti kwa Mulungu."
Mawu anaziriwa siabwino pa malamulo a Chisilamu, ngakhale kuti anthu
ambiri amakonda kuchita naziri poganizira kuti akatero Mulungu awayankha
mwachangu namaganiziranso kuti naziri nchinthu chabwino m'Chisilamu
pomwe chili chosafunika m'Chisilamu.
Kusafunika kwa naziri m'Chisilamu kuli kotere: Umati, "Mulungu akandichitira
chakutichakuti inenso ndichita chakutichakuti." Mawu oterewa sali mawu
abwino ndiponso akusonyeza kupanda mwambo ndiponso akusonyeza
umbombo.
Chifukwa cha kuti munthu ofuna kupereka kanthu sanganene kuti "Muyambe
mwandichitira chakuti ndipo ndikupatsani." Koma ngakhale zili choncho
akwaniritsebe malonjezowo. Koma ngati malonjezowo ali pachinthu choletsedwa
asawakwaniritse, ndipo m'malo mwake apereke dipo.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 3
94
r frjA-i
T S^aJi 5jj-»
Wltf*
zambiri. Ndipo (Zoterezi )
sakumbuka koma Eni nzeru okha.
270. Ndipo chilichonse chomwe
mungapereke Kapena naziri
(lonjezo) iliyonse yomwe
Mwalonjeza Mulungu, Ndithudi,
Mulungu akudziwa Zonsezi. Ndipo
anthu ochita Zoipa sadzakhala ndi
athandizi.
271. Ngati mupereka sadaka
moonetsera, Ndibwino; Ngati
mungaipereke mobisa,
Ndikuipereka kwa osauka,
umenewo Ndiubwino woposa kwa
inu. Ndipo akufafanizirani zoipa
Zanu (ngati mutero). Ndipo
Mulungu Akudziwa nkhani zonse
Za zimene mukuchita.
272. Siudindo wako
kuwaongola, koma Mulungu
amamuongola amene Wamfuna,
(udindo wako Nkulalikira kokha).
Ndipo Chuma chilichonse chimene
mungachipereke, (Phindu lake) lili
painu eni, ndipo musapereke
Pokhapokha pofunafuna chikondi
cha Mulungu. Ndipo chuma
chilichonse chimene
Mungachipereke adzakubwezerani
Mokwanira (mphoto yake), Ndipo
simudzaponderezedwa. l
1 Apa akumuuza Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) pamodzi ndi
aliyense wolamula kuchita zabwino ndikuletsa kuchita zoipa kuti udindo wawo
nkufikitsa uthengawo. Pa iwo palibe vuto ngati anthuwo savomereza, iwo
9 1 9&' 9 *?> ' h9 l f *f <
Siirat 2. Al-Baqarah Juzu 3
95
T tjfr\
t djijl 0jJ-*»
273. (Sadakazo ziperekedwe)
kwa amphawi amene
Atsekerezedwa panjira ya
Mulungu, amene Sangathe
kuyenda padziko (Kukachita
ntchito yopezera Zofunika pamoyo
wawo). Amene Sadziwa za
chikhalidwe chawo,
Amawaganizira kuti ngolemera
Chifukwa chakudziletsa kwawo
(Kupemphapempha) .
Ungawazindikire (Kuti
ngosowedwa) ndi zizindikiro
zawo. Sapempha anthu mwaliuma.
Ndipo chabwino chilichonse
chimene Mukupereka, ndithudi,
Mulungu ali Wodziwa Zaicho.
274. Amene akupereka chuma
Chawo usiku ndi usana, Mobisa
ndi moonekera, Ali ndi malipiro
awo Kwa Mbuye wawo; Ndipo
paiwo sipadzakhala Mantha,
ndiponso sadzadandaula.
275. Amene akudya riba
(chuma cha katapira) Sadzauka
(M'manda) koma monga Mom we
amaimira munthu okhudzidwa Ndi
ziwanda, mwamisala. (Ndipo) izi
nchifukwa chakuti amanena:
"Malonda ngolingana ndi
katapira," pomwe Mulungu
waloleza malonda ndipo waletsa
Katapira. Ndipo amene wamufika
9 9 '9 * 4
A "A\ Sfl S S ' \9-l.M
adzapezabe mphoto yolamulira zabwino ndikuletsa zoipa ngakhale kuti
sanawatsatire.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 3
96
r *jJi-i
T 5yJl ojj^
ulaliki Wochokera kwa Mbuye
wake (woletsa Katapira) nasiya,
choncho chomwe Chidapita
nchake. Ndipo chiweruzo chake
Chili kwa Mulungu (akaona
chochita naye). Koma amene
abwerera (kuchita malonda
Akatapira), amenewo ndiwo anthu
akumoto, Mmenemo adzakhalamo
muyaya.
276. Mulungu amachotsa
madalitso Pa (chuma cha) katapira
Ndipo amaika madalitso
Pachaulere. Ndipo Mulungu
Sakonda aliyense
Wosakhulupirira, wamachimo
ambiri.
277. Ndithudi, amene
akhulupirira, nachita Zabwino,
napemphera Swala moyenera Ndi
kupereka chopereka (Zakati) Iwo
akapeza malipiro Awo kwa Mbuye
wawo. Ndipo pa iwo sipadzakhala
Mantha ndiponso sadzadandaula.
278. E! inu amene
mwakhulupirira! Opani Mulungu,
ndipo siyani Zimene zatsalira
m'katapira, Ngati inu mulidi
okhulupirira.
1 Ndime iyi yikuletsa kukongoza m'njira yakatapira. Mulungu akumuopseza
mwamphamvu munthu wodya riba. Akumuuza kuti adziwe kuti ali pankhondo
yolimbana ndi Mulungu. Mulungu akukalipa zedi kwa anthu ochita malonda
akatapira. Tero pewani kuchita malonda akatapira.. Kodi inu muli ndi nyonga
zomenyerana ndi Mulungu?
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 3
97
r *j*-i
t djAJf $JJ-»
279. Ngati simuchita
(zimenezo), Dziwani kuti
mukulimbana ndi Mulungu ndi
Mtumiki Wake. Ndipo ngati
mulapa, maziko Achuma chanu
ndi anu. Musapondereze, ndiponso
Musaponderezedwe.
280. Ndipo ngati wokongola ali
ndi mavuto, Choncho (wokongoza)
amdikire mpaka Apeze bwino.
Ngati inu (okongoza
Mungakhululuke pakusiya
Kuitanitsa ngongole) muisintha
kuti Ikhale sadaka, ndibwino
kwainu ngati Mukudziwa
(zimenezo).
281. Ndipo liopeni tsiku lomwe
inu Mudzabwezedwa kwa
Mulungu. Ndipo kenako munthu
aliyense Adzalipidwa mokwanira
pazonse Zimene adachita (Ndi
manja ake), Ndipo iwo
sadzaponderezedwa.
282. E inu amene
mwakhulupirira!
Mukamakongozana Ngongole kwa
nyengo yodziwika Ilembeni. Ndipo
mlembi pakati Panu alembe
mwachilungamo; Ndipo mlembi
asakane kulemba Monga momwe
Mulungu Wamphunzitsira;
choncho alembe. Ndipo alakatule
(mawu olembedwawo Ndi
wokongolayo) yemwe ngongole ili
paiye. Nayenso aope Mulungu,
h&pm
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 3
98
r >>»
x SjiJi «jj-»
Mbuye wake, ndipo asapungule
Chilichonse M'menemo
(m'ngongole). Ndipo ngati
wokongola ndiozelezeka kapena
Wofooka, kapena iye mwini
sangathe Kulembetsa (Momveka),
choncho amulembetsere
Myang'aniri (Wakili) wake
(yemwe Akuyang'anira zinthu
zake) mwachilungamo. Ndipo
funiraponi mboni ziwiri Zochokera
mwa anthu anu aamuna (Asilamu).
Koma ngati amuna awiri Palibe,
choncho apezeke Mwamuna
mmodzi ndi akazi awiri (Kuti
aikire umboniwo), amene
mumavomereza Kukhala mboni
kuti ngati mmodzi mwaiwo (Akazi
awiriwo) angaiwale Mmodzi
wawo akumbutse winayo. Ndipo
Mboni zisakane zikaitanidwa.
Ndiponso Musanyozere kulemba
(ngongoleyo) yaing'ono Kapena
yaikulu mpaka nyengo yake.
Zimenezo (Kulembako) ndibwino
kwa Mulungu, ndipo
Ncholungama zedi kumbali
yaumboni, ndiponso Nchothandiza
kuti musakhale ndi chipeneko.
Koma akakhala malonda omwe ali
Pompo omwe mukupatsana pakati
panu (tsintho) Sikulakwa kwainu
kusalemba. Koma Funani mboni
pamene mukugulitsana. Komatu
Asavutitsidwe mlembi ndiponso
mboni. Ngati Mutachita zimenezo
•r£ti-<
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 3
99
Tf>l
Y OjiJl Ojj-*
(zoletsedwazo) kumeneko Ndiko
kutuluka m'chilamulo cha
Mulungu wanu, ndipo opani
Mulungu, Mulungu
akukuphunzitsani. Ndipo Mulungu
Ngodziwa chilichonse. 1
283. Ngati muli paulendo, ndipo
Simudapeze mlembi, choncho
(Wokongoza) apatsidwe chikole
(Pinyolo) m'manja mwake. Ngati
wina Wasungitsa mmodzi wainu
chinthu (Omuyesa wokhulupirika)
choncho Amene wayesedwa
wokhulupirikayo Abweze
chinthucho kwamwini wake,
Ndipo aope Mulungu, Mbuye
wake. Ndipo musabise umboni
(Ngakhale uli wokuipirani). Ndipo
Amene abise ndiye kuti mumtima
1 Apa akuwalimbikitsa anthu kuti azilemba akamakongozana zinthu kuti
pasakhale mkangano ndikukanirana kuti sanakongozane. Ngakhale
ngongoleyo ikhale yochepa pafunika ndithu kulemba. Ndipo polembetsa
ngongoleyo wokongolayo ndiye adzinena mawu olembedwawo poopa kuti
akayankhula wokongoza akhoza kuonjeza mawu ndipo wokongola nkuchita
manyazi kumbweza pakuti mkono wopempha ngwapansi pomwe wopereka
ngwapamwamba. Ndipo pamene wolemba akuuzidwa kuti asawakanire
kuwalembera osadziwa kulemba, akutanthauza kuti anthu azithandizana
pakati pawo. Ndipo olemba akuwalangizanso kuti alembe zokhazo zomwe
akuuzidwa ndipo afunirepo mboni zotsimikiza kuti alembadi. Ndipo mbonizo
zisainire pamenepo. Oikira umboni afunika kukhala amuna awiri a Chisilamu.
Ngati palibe amuna awiriwo, mmalo mwa mwamuna mmodzi zilowe mboni
ziwiri za chikazi chifukwa chikumbumtima chaakazi nchochepa poyerekeza
ndi chaamuna. Ndipo anthu akuwauzanso kuti akawapempha kuti aikire
umboni pachinthu asakane. Kuikira umboni ndi ntchito yabwino yotsimikizira
choona ndi kukana chonama. Koma pamalonda ogulitsana dzanja ndi dzanja
sipafunika kulemba koma pamangofunika mboni basi. Ndipo pomwe
kwanenedwa kuti "Asavutitsidwe olembawo ndi oikira umboniwo" akusonyeza
kuti ngati ntchito yolembayo ndi kuikira umboniwo nzotenga nthawi yaitali
kotero kuti olembawo ndi mbonizo iwachedwetsera ntchito zawo zomwe
amapezera zowathandiza pamoyo wawo, ayenera kuwalipira.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 3
100
r *>i
t 3jiJl 5jj-*»
Mwake mwalowa utchimo; ndipo
Mulungu akudziwa zonse zimene
mukuchita. 1
284. Zonse zakumwamba ndi
Zapansi nza Mulungu. Kaya
Muonetsera poyera zomwe Zili
m'mitima mwanu kapena
Kuzibisa, Mulungu adzakuchitirani
Nazo chiwerengero. Kenako
Adzakhululukira amene wamfuna
(atalapa). Ndipo adzamlanga
amene Wamfuna (akapanda
kulapa). Ndipo Mulungu
Ngokhoza chilichonse.
285. Mtumiki wakhulupirira
zimene zavumbulutsidwa Kwa iye
kuchokera kwa Mbuye wake.
Naonso Asilamu (akhulupirira).
Onse Akhulupirira Mulungu,
Angelo Ake, mabuku Ake ndi
atumiki Ake. (I wo pamodzi ndi
Mtumiki wawoyo akunena kuti):
"Sitingalekanitse aliyense pakati
pa atumiki Ake. (Onse
1 Apa akunena kuti ngati anthu ali pamalo pomwe palibe wodziwa kulemba
ndipo akukongozana, wokongozedwayo apereke chikole kwa wokongoza kuti
achisunge wokongozayo. Ndipo adzabwezera akadzabweza ngongoleyo.
Ngati atalephera kubweza ngongoleyo chikolecho chigulitsidwe ndi muweruzi
nkumpatsa wokongozayo ndalama zolingana nzomwe adamkongoza.
Zotsalira pachinthu chogulitsidwacho azipereke kwa mwini chikolecho.
Uwu ndiwo ubwino wachikole pa Malamulo a Chisilamu. Akalephera kubweza
ngongoleyo chinthucho chimagulitsidwa ndi Boma ndikumpatsa mwini
ngongoleyo choyenerana naye pomwe chotsaliracho amachipereka kwa
mwini wake.
Kwa amene wagwirizira chikolecho saloledwa kuchita nacho chilichonse.
Ngati akuchita nacho ntchito nkumachidyerera ndiye kuti akuchita machitidwe
akatapira omwe ali oletsedwa. Koma chinthucho angochisunga.
Siirat 2. Al-Baqarah Juzu 3 ioi T *jk-\
t SyLJl 5jj-*»
tikuwakhulupirira)." Ndipo
akunena: "Tamva ndiponso
tamvera. (choncho
Tikukupemphani) chikhululuko
chanu, E! Mbuye Wathu! Ndipo
kwa Inu nkobwerera." 1
286. Mulungu sakakamiza
mzimu Uliwonse koma chimene
chili cholingana Ndi kukhoza
kwake. (Ndipo phindu la) Zimene
mzimuwo udapeza ndilake
Ndiponso kuluza kwazomwe
Udapeza nkwake. (Asilamuwo
1 (Ndime 285-6) Ndime ziwirizi zili ndiubwino ndi madalitso ambiri monga
momwe ilili ndime ya Ayatu Kursii yanambala 255 m'sura yomweyi.
Akutilangiza kuziwerenga ndimezi m'malo monse momwe Ayatu Kursii
imawerengedwa. Chimodzi mwazimenezo ndikuti iwo amavomereza atumiki
onse a Mulungu amene adadza patsogolo pa Mneneri Muhammad (madalitso
ndi mtendere zikhale naye). Qur'an yonse ikuphunzitsa Asilamu kuti
asasiyanitse pakati pa aneneri. Koma awavomereze onse ndi kuwakhulupirira
amene adadza patsogolo pa Mtumiki Muhammad (SAW). Mtumiki
Muhammad (SAW) ndiye womaliza mwa Aneneriwo. Ndipo amadziwika ndi
dzina lakuti "Khatama nNabiyyina" "Womaliza mwa Aneneri." Ndipo amene
sakhulupirira kuti Muhammad (SAW) ngomaliza mwa aneneri nakhulupirira
munthu wamba yemwe akungodzinamiza kuti iye ndi mneneri, monga momwe
chikhulupiriro cha Akadiyani chilili ndiye kuti iyeyo watuluka m'Chisilamu ndipo
ndi munthu wakunja.
Asilamu sakana mneneri aliyense mwa Aneneri omwe adalipo Mtumiki
Muhammad (SAW) asanadze. Koma iwo amakhulupirira kuti malamulo
akayendetsedwe kazipembedzo zawo kadafafanizidwa chifukwa chakudza
kwa mtumiki Muhammad (SAW). Nyengo ino ndinyengo yotsatira mtumiki
Muhammad (SAW) pazochitachita. Koma pazinthu zokhudza chikhulupiriro,
Aneneri onse adadza ndi lamulo limodzi monga momwe Mulungu
akufotokozera m'ndime ya 13, Surat Shura.
Ndipo m'ndime zimenezi za 285 ndi 286 zikuphunzitsanso miyambo
yaChisilamu ndi mapemphero (maduwa) momwe tingampemphere Mulungu.
Ndimezi zikufotokoza za chisomo cha Mulungu chomwe chili pa ife anthu Ake
kuti Mulungu sakakamiza koma chimene angathe kuchichita akapolo Ake.
Ndiponso sawalanga ngati atachita zinthu molakwitsa kapena moiwala.
Ndime ziwirizi zikusonyeza makhalidwe Asilamu ndi zinthu zawo zimene
amazikhulupirira.
Surat 2. Al-Baqarah Juzu 3 102 ? *> (
Y SyLJl ^JJ^
amanena) "O! Mbuye wathu!
Musatilange tikaiwala Kapena
tikalakwitsa, O, Mbuye wathu!
Musatisenzetse mtolo
(wamalamulo) monga
munawasenzetsera amene adalipo
Patsogolo pathu. O! Mbuye
Wathu! Musatisenzetse chimene
Sitingachithe. Tifafanizireni,
tikhululukireni Machimo athu,
ndiponso tichitireni chifundo. Inu
Ndinu mtetezi wathu. Choncho
Tithangateni ku anthu
osakhulupirira."
Siirat 3. Al-'Imran Juzu 3
103 1" *>• T Wj** J T hf
SURAT AL-'IMRAN III *
Iyi ndi imodzi mwa Sura zomwe zidavumbulukira ku
Madina, ndipo ndiimodzi mwasura zitalizitali.
Surayi yafotokoza ngodya ziwiri zofunika m'chipembedzo
cha Chisilamu zomwe ndi izi:-
Ngodya yoyamba yafotokoza zachikhulupiriro ndi kupereka
maumboni ndi zisonyezo zosonyeza umodzi wa Mulungu. Ngodya
yachiwiri yafotokoza zamalamulo makamaka onena za kamenyedwe
kankhondo yomenyera panjira ya Mulungu.
Tsono m'tsatanetsatane wangodya yoyamba ija m'suramu
mwadza mawu otsimikiza kuti Mulungu ndi mmodzi palibe
wachiwiri kapena wachitatu. Ndipo alibe bambo, mwana kapena
mkazi. Surayi yatsimikizanso kuti Mulungu adasankha anthu
ena kuti akhale aneneri ncholinga choti afikitse kwa anthu
uthenga wake. Ndipo yakambanso za choonadi cha Qur'an ndi
kutsutsa zabodza zomwe anthu amachinamizira Chisilamu ndi
Qur'an. Sura ya Bakara yafotokoza zambiri zachikhalidwe cha
Ayuda ndi zolinga zawo zomwe nkukonda chiwembu ndi kuswa
mapangano. Tsono sura ya Al-Imran yafotokoza za Akhirisitu
omwe adatsutsana kwambiri ndi Mtumiki (madalitso ndi
mtendere zikhale naye) pankhani yoti Yesu ndi mwana wa
Mulungu kapena kuti ndi Mulungu amene pachifukwa choti
anabadwa opanda tate. Ndipo iwo adatsutsanso uthenga wa
Muhammad (SAW) ndi kumkana kuti simtumiki ndikutinso
Qur'an sibuku la mawu a Mulungu. Surayi yakamba zaiwowa
pafupifupi theka la surayi powayankha ndi kuwatsutsa pamawu
awo omwe adali kukamba okhudza Mariya ndi Yesu popereka
maumboni ndi zizindikiro zotsutsa kuti iwo sadali milungu.
M'suramu mwakambidwanso nkhani za Ayuda pamodzi ndi
kuwachenjeza Asilamu kuchiwembu chawo. Tsono
patsatanetsatane wangodya yachiwiri, surayi yafotokoza ena
mwa malamulo monga malamulo a Haji, Jihadi, zinthu zonena
Surat 3. Al-'Imran Juzu 3 104 T *>»
T &j+* J^ 5jj-*
za katapira (riba) ndi lamulo lonena za munthu wokaniza
kupereka zakati. Mwakambidwanso m'suramu
mwatsatanetsatane zankhondo, monga nkhondo ya Badri ndi
Uhudi ndi maphunziro omwe Asilamu adatolamo m'nkhondozi.
I wo adapambana pa nkhondo ya Badri nagonja pa nkhondo ya
Uhudi, chifukwa chakusamvera kwawo langizo la Mtumiki
(madalitso ndi mtendere zikhale naye). Ndipo pambuyo
pogonjetsedwa adatukwanidwa ndi Amunafikina ndi anthu
osakhulupirira Mulungu. Kenako Mulungu anawafotokozeranso
kuti cholinga cha Mulungu powalekerera Asilamu kuti agonje
pankhondoyi, nkuti aonetsere poyera mwaiwo omwe adali
ndichikhulupiriro champhamvu ndiomwe adali achinyengo.
Surayi yafotokoza mwatsatanetsatane za amthirakuwiri omwe
cholinga chawo chinali kudzetsa chisokonezo pakati pa
Asilamu. Ndipo Surayi yamaliza nkulangiza anthu kuti alingarire
za zolengedwa za Mulungu zakumwamba ndi zapansi zomwe
zili zododometsa mkapangidwe kake kaluso zomwenso
zikusonyeza kuti Mulungu Ngwamphamvu zoposa,Wopambana
pachilichonse ndipo palibe chokanika kwa lye.
Surat 3. Al-'Imran Juzu 3 105 V *>» T 0\j** JT Sj^-
SuratAl-'Imranlll
:-""
%\..mm&;2:$:i
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1 . Alif-Lam-Mim}
2. Mulungu (ndi mmodzi).
Palibe winanso Wopembedzedwa
mwa choonadi koma lye yekha,
Wamoyo Wamuyaya, Woimira
Ofr£\<£i$\&\j
-^
Ndime makumi asanu ndi atatu zamsurayi zidavumbuluka chifukwa
chanthumwi za Akhrisitu zochokera ku Najirani pamene zidadza kwa Mtumiki
(madalitso ndi mtendere zikhale naye). Nthumwizi zinali 60 okwera pa
nyama.Mwa iwo mudali anthu khumi ndi anayi omwe adali olemekezeka awo.
Ndipo atatu mwa iwo adali akuluakulu awo omwe ndi: Abdul Masihi, yemwe
adali mtsogoleri wawo, Al-Ayihamu, yemwe adali mlangizi wawo, Abu Harisa
bun Al-Kama, yemwe adali wansembe wawo. Pamene adakumana ndi
Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) atatu aja mwa iwo ndiwo
adalankhula nati: "Yesu 1 ndiye Mulungu chifukwa chakuti iye adali kuutsa
maliro." Penanso adati: "lye ndi mwana wa Mulungu chifukwa choti inu
simukudziwa kuti Mbuye wathu Mulungu ngwamoyo wamuyaya, safa, pomwe
adalibe bambo." Natinso: "lye ndi mmodzi mwa atatu chifukwa chakuti
Mulungu adati, "tidachita,"
"tidati." Akadakhala mmodzi akadati "Ndidachita; ndidanena." Mtumiki
Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale naye) adati kwaiwo: "Kodi Yesu
ngwakufa?" Iwo adati: "Inde." Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye)
adatinso: "Kodi simukudziwa kuti sipangakhale mwana pokhapokhapo
atafanana nditate wake?" Iwo adati: "Inde." lye adatinso: "Kodi simukudziwa
kuti Mbuye wathu Mulungu ndiYemwe akuimiririra chinthu chilichonse
pochisunga ndi kuchipatsa zofuna zake? Kodi Yesu amachita chilichonse
mwazimenezi?" Iwo adati: "lyayi" Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale
naye) adatinso: "Kodi simukudziwa kuti kwa Mulungu palibe chingabisike
chakumwamba ndi chapansi? Nanga Yesu amadziwa chilichonse mwazimenezo
osati chokhacho chimene wadziwitsidwa?" Iwo adati: "lyayi." Ndipo iye
adatinso: "Kodi simukudziwa kuti Mbuye wathu Mulungu sakudya chakudya
ndipo sakumwa ndiponso sadzithandiza pomwe Yesu adali kudya ndi kumwa
ndipo adali kudzithandiza?" Iwo adati: "Inde." Ndipo Mtumiki (madalitso ndi
mtendere zikhale naye) adati: "Nanga iye angakhale bwanji Mulungu monga
momwe mukunenera?" Onse adangoti kakasi. Komabe adapitiriza kumkana
Mtumiki Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale naye). Choncho
Mulungu chifukwa cha iwo adavumbulutsa ndime zam'surayi kuyambira
ndime 1 mpaka 80.
Surat 3. Al- 4 Imran Juzu 3
106
r *j*-i
T Olj^P JT 5jj-*
Ndi kuteteza chilichonse.
3. Wakuvumbulutsira Buku
Mwachoonadi, lomwe
Likutsimikizira zomwe Zidalipo
patsogolo pake. Ndipo
adavumbulutsa Taurat ndi Injili -
(Chipangano Chatsopano).
4. Kale, kuti (mabukuwo)
akhale chotsogolera Anthu.
Ndipo adavumbulutsa (Qur'an)
Cholekanitsa pakati pa choonadi
ndi chonama. 2 Ndithudi, aja
amene sadakhulupirire zizindikiro
za Mulungu, adzakhala ndi
chilango chaukali. Ndipo
Mulungu ngwamphamvu
Zoposa, wobwezera (Chilango
mwaukali).
5. Ndithudi, kwa Mulungu
Sikungabisike chilichonse
Chapansi ngakhale chakumwamba.
6. lye ndi Yemwe
amakulinganizani Muli m'mimba
mmaonekedwe Anu mmene
Mulungu ndiyekhayo woti nkumpembedza. Palibe wina wompembedza
mwachoonadi koma lye basi. Padziko lonse lapansi ndi kumwamba palibe mwini
mphamvu zoposa wogonjetsa chilichonse koma lye yekha basi. lye ndi Yemwe
amadzetsa zabwino ndikubweretsa zoipa, osati wina aliyense. lye Ngwamoyo
Wamuyaya, moyo wopanda chiyambi ndiponso wopanda malekezero. lye
Ngwachikhalire kuyendetsa zinthu zazolengedwa zake. Thambo ndi nthaka
adazikhazikitsa. Apa nkuti Mneneri Yesu asanamlenge. Choncho, Yesu sali
Mulungu koma ndimmodzi wa aneneri.
2 Tanthauzo la ndime iyi nkuti yakuvumbulukira iwe Muhammad (SAW) iyi
Qur'an mwachoonadi popanda chipeneko kuti idachokera kwa Mulungu.
Yatsika kupyolera mkudziwa Kwake itsimikizire zimene ztdali m'mabuku
apatsogolo pake. Ndipo pazimenezi angelo ndimboni.
Surat 3. Al-'Imran Juzu 3
107 r *>»
V OIj^p JT 3jj--
akufunira. Palibe wopembezedwa
Mwachoonadi koma lye;
Ngwamphamvu zoposa,
Ngwanzeru zakuya.
7. lye ndiYemwe
wakuvumbulutsira Buku (ili la
Qur'an), lomwe mkati Mwake
muli ndime zomveka zomwe Ndi
maziko a Bukuli. Ndipo Zilipo
zina zokuluwika. Koma amene
M'mitima mwawo muli kusokera,
Akutsata zomwe zili zokuluwika
Ndi cholinga chofuna kusokoneza
Anthu, ndikufuna kudziwa
tanthauzo Lake lenileni, Palibe
amene akudziwa Tanthauzo lake
lenileni koma Mulungu basi.
Koma Amene azama
pamaphunziro, amanena:
"Tawakhulupirira (ma aya
amenewa). Onse Ngochokera kwa
Mbuye wathu," Ndipo palibe
angakumbukire Koma eni nzeru
basi.
8. (Anzeruwo amanena): " O!
Mbuye wathu! Musaikhotetse
mitima Yathu pambuyo
potiongola. Tipatseni chifundo
chochokera Kwa Inu. Ndithudi,
Inu Ndinu wopatsa kwambiri.
9. O! Mbuye wathu! Inu ndinu
Wosonkhanitsa anthu patsiku
Lopanda chikaiko, Ndithudi,
Mulungu Saswa lonjezo.
I)
Surat 3. Al-'Imran Juzu 3
108
r *>i
T OI^aP JT 5jj-*»
10. Ndithu, amene
sadakhulupirire, Chuma chawo
sichidzawathandiza Chilichonse
ngakhalenso Ana awo, kuchilango
cha Mulungu. Ndipo iwo Ndi
nkhuni zakumoto.
11. (Khalidwe la awa
osakhulupirira, amumbadwo Wako
iwe Mneneri Muhammad {SAW},
liri) Ngati khalidwe la anthu a
Farawo ndi amene Adalipo
pambuyo pawo. (Iwo) adatsutsa
Zisonyezo zathu. Choncho,
Mulungu Adawakhaulitsa
chifukwa cha machimo awo.
Ndipo Mulungu Ngolanga
mwaukali.
12. Auze amene
sadakhulupirire: "Posachedwapa
mugonjetsedwa
Ndikusonkhanitsidwa
ndikuponyedwa Kumoto. Taonani
kuipa kwa Malo wokhazikika." 1
^ 9
Mawu adalandiridwa kuchokera kwa Said bun Jubeir omwe iye
adawalandiranso kuchokera kwa Ikirama pomwe nayenso Ikirama adawalandira
kuchokera kwa Ibinu Abbas (Mulungu asangalale nawo onse). lye adati:
"Ndithudi, Mtumikl (madalitso ndi mtendere zikhale naye) pamene
adagonjetsa Akuraishi pankhondo ya Badri nabwerera ku Madina
adawasonkhanitsa Ayuda mumsika wa Bani Kainuka nawachenjeza kuti
chingawapeze chomwe chidawapeza Akuraishi. Iwo adati: "Usanyengedwe
ndizimenezo.
Ndithudi, iwe unakumana ndi mbuli za anthu zomwe sizidziwa kamenyedwe
kankhondo. Ndipo nchifukwa chake wawagonjetsa. Ukadamenyana ndi ife
ukadadziwa kuti ife ndife anthu."
Pachifukwa ichi idavumbulutsidwa aya (ndime) yakuti: "Nena (kwa iwo iwe
Muhammad {SAW}): "Inu Ayuda mugonjetsedwa posachedwapa pompano
padziko lapansi. Chuma chanu ndi ana anu zisakunyengeni. Kupambana
Surat 3. Al-'Imran Juzu 3 109 T *>»
T OIj^p JT djj^t
13. "Ndithudi, padapezeka
chisonyezo chachikulu Kwa inu
m'magulu awiri omwe adakumana
(Tsiku lankhondo ya Badri),
pomwe gulu Limodzi limamenya
(nkhondo) panjira ya Mulungu,
pamene linalo lokanira (ndipo
gululo) Linkawaona (Asilamu)
kukhala ochuluka kawiri Kuposa
ilo, poona ndi maso awo. Ndipo
Mulungu amamlimbikitsira
mphamvu Ndi chipulumutso chake
amene wamfuna. Ndithudi,
m'zimenezo muli malingaliro
(akulu) Kwa eni kupenyetsetsa
mwanzeru."
14. Kwakometsedwa kwa anthu
kukonda Zilakolako (Zamoyo
monga) akazi, ana, Milumilu
yachuma cha golide ndi Siliva ndi
mahachi oyang'aniridwa Bwino,
ziweto, ndi mbewu. Izo ndi
zosangalatsa za moyo Wadziko
lapansi (zomwe sizilikanthu).
Koma kwa Mulungu ndiko kuli
Mabwerero abwino.
15. Nena: "Kodi ndikuuzeni
zomwe Zili zabwino kuposa
zimenezo? Kwa omwe ali olungama,
Akapeza kwa Mbuye wawo Minda
yomwe pansi Pake ndi patsogolo
KsJ6 9 9 9% *\' } *' * 9
sikuli pachifukwa chakuchuluka kwanu, koma kuli m'manja mwa Mulungu
Woyera."
Mawuwa adatsimikizika powapha a Bani Nazwiri ndi kugonjetsa mzinda wa
Khaibar.
Surat 3. Al-'Imran Juzu 3 110 ? *> (
T OIj^p JT djy*
pake Mitsinje ikuyenda;
Adzakhala Mmenemo muyaya
ndikulandira Akazi oyeretsedwa
ndi chiyanjo Chochokera kwa
Mulungu. Ndipo Mulungu akuona
Akapolo ake onse.
16. Omwe akunena: "Mbuye
wathu! Ndithudi, ife takhulupirira.
Choncho tikhululukireni Machimo
athu ndikutipewetsa Kuchilango
chamoto."
17. Opirira onena zoona,
omvera, Opereka chaulere ndi
Opempha chikhululuko Nthawi
yam ' bandakucha.
18. Mulungu (mwini) akuikira
umboni kuti: "Palibe
wopembedzedwa mwachoonadi
koma lye basi." Ndipo akuikiranso
umboni (Zomwezi) angelo ndi eni
nzeru (kuti lye) Ngokhazikitsa
chilungamo. Palibe wina
Wopembedzedwa mwachoonadi
koma lye. Ngwamphamvu zoposa,
Ngwanzeru zakuya.
19. Ndithudi, chipembedzo
(choona) kwa Mulungu ndi
Chisilamu. Ndipo amene
Adapatsidwa Buku (Ayuda ndi
Akhrisitu) sadatsutsane koma
pambuyo Powabwerera
kuzindikira. (Adatsutsana)
Chifukwa chadumbo lomwe lidali
Pakati pawo. Ndipo amene
M
&&&£m
Surat 3. AI- 4 Imran Juzu 3
111
r*>»
T OIj*p JT $jj*t
akukana Zisonyezo za Mulungu,
(Mulungu akamulanga pa tsiku
lachiweruzo). Ndithu Mulungu
Ngwachangu powerengera.
20. Ngati (osakhulupirira)
atsutsana nawe, Nena:
"Ndayang'anitsa nkhope yanga
Kwa Mulungu (ndadzipereka kwa
lye) Pamodzi ndi amene
anditsata." Ndipo Nena kwa onse
adapatsidwa Buku (Ayuda Ndi
Akhrisitu) ndi osadziwa kulemba
Ndi kuwerenga (Arabu): "Kodi
mwagonjera (Kwa Mulungu)?"
Ngati agonjera ndiye Kuti
aongoka: Koma ngati
atembenukira Kumbali, udindo
wako ndikufikitsa uthenga Basi.
Ndipo Mulungu akuona akapolo
ake onse.
21. Ndithudi, amene akutsutsa
Zizindikiro za Mulungu ndikupha
Aneneri popanda choonadi
Ndikuphanso anthu omwe
Akulamula (kuchita) zolungama,
Auze nkhani ya chilango
chopweteka.
22. Iwowo ndi omwe zochita
Zawo zaonongeka Padziko lapansi
ndi patsiku Lomaliza. Ndipo iwo
sadzapeza athandizi.
23. Kodi sukuwaona omwe
apatsidwa Gawo la Buku (la
Mulungu)? Akuitanidwa ku Buku
^\$^m&$\'dm
Surat 3. Al-'Imran Juzu 3
112
r *>i
T b\y>* JT 5jj-*»
la Mulungu Kuti liwaweruze
pakati pawo; Kenako gulu Una la
iwo Likutembenukira kumbali iwo
ali onyoza.
24. Zimenezo (kusalabadira
malamulo a Mulungu) Nchifukwa
chakuti amanena: "Sudzatikhudza
Moto koma masiku ochepa basi".
Ndipo Zawanyenga
pachipembedzo chawo zomwe
Adali kupeka (kuti
adzakhululukidwa kapena
Kulangidwa masiku ochepa okha).
25. Kodi zidzakhala zotani
pamene Tidzawasonkhanitsa tsiku
lopanda Chikaiko? Ndipo mzimu
uliwonse Udzalipidwa mokwanira
pa Zomwe udachita. Ndipo iwo
Sadzaponderezedwa.
26. Nena "O! Mbuye wanga!
Mwini Ufumu wonse.
Mumapereka ufumu kwa yemwe
mwamfuna. Ndipo Mumachotsa
ufumu kwa yemwe Mwamfuna.
Mumapereka ulemerero Kwa
emwe mwamfuna, ndipo
Mumamsambula yemwenso
mwamfuna. Ubwino wonse uli
1 Ndimeyi anthu omasulira Qur'an akuti ikufotokoza nkhani za Ayuda pamene
adadza kwa Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) mmodzi mwaiwo
atachita chiwerewere kuti arrive chilamulo chawochita chiwerewere. Mtumiki
(madalitso ndi mtendere zikhale naye) anagamula kuti amulase ndi miyala
mpaka afe. Koma iwo anakana. Anati; "M'Buku lathu mulibe chilamulo
chotere." Ndipo adawauza kuti abwere nalo bukulo. Atabwera nalo anapeza
kuti chilamulocho chilipo. Ndipo anawalasa miyala. Zitachitika tero, Ayuda
anakwiya.
>&&m6$^m&\$
fi:?'^^^
9 >."
Surat 3. Al-'Imran Juzu 3
113
T *jir\
T Jtj^P JT $jj--
m'manja mwanu. Ndithudi, Inu
ndinu Wokhoza chirichonse.
27. "(Inu) mumalowetsa usiku
muusana (Ndikukhala usana
wautali monga m'nyengo
Yotentha). Ndipo Mumalowetsa
usana muusiku (Nkukhala usiku
wautali monga m'nyengo
Yachisanu). Mumatulutsa cha
moyo M'chakufa; Ndipo
mumatulutsa chakufa
M'chamoyo. Ndipo mumapatsa
Riziki (Chakudya) amene
mwamfuna Mopanda
chiwerengero." 1
28. Asilamu asapale ubwenzi
osakhulupirira Kusiya Asilamu
anzawo. Amene Achite zimenezo,
sadzakhala ndi Chilichonse
pachipembedzo cha Mulungu,
kupatula (kupalana Nawo ubwenzi
mwachiphamaso) Chifukwa
chakudzitchinjiriza kwa iwo.
Ndipo Mulungu lye mwini
Akukuchenjezani (za chilango
chake). Ndipo kobwerera ndi Kwa
Mulungu (basi).
29. Nena: "Ngati mubisa
zomwe Zili m'zifuwa zanu, kapena
Kuzionetsa (poyera), Mulungu
Akuzidziwa. lye akudziwa Zonse
1 M'njere mumatuluka mmera. Ndipo njere imatuluka mummera. Dzira limatuluka
m'nkhuku, ndipo nkhuku imatuluka m'dzira. Wosakhulupirira amabereka
wokhulupirira. Ndipo wokhulupirira amabereka wosakhulupirira.
Surat 3. Al-'Imran Juzu 3 114 T *>i
T OIj*p JT 5jj-i
hW-*
&&&&&&(&&$&
©;*-?->->-
*&&\$t&$ȣ
zakumwamba Ndi zapansi. Ndipo
Mulungu Ngokhoza chilichonse."
30. "Tsiku lomwe mzimu
uliwonse Udzapeza zabwino
zomwe Udachita zitabweretsedwa,
Ndiponso zoipa zomwe udachita;
Udzalakalaka kuti pakadakhala
Mtunda wautali pakati
Pamachimo ake ndi iye. Ndipo
Mulungu Mwini Akukuchenjezani
za chilango Chake. Ndipo
Mulungu ngoleza Kwa akapolo
ake. 1
31. Nena: (iwe Mtumiki) "Ngati
inu Mukumkonda Mulungu, tsatani
ine; Mulungu akukondani
Ndikukukhululukirani machimo
Anu. Ndipo Mulungu
Ngokhululuka, Ngwachisoni." 2
32. Nena: "Mverani Mulungu
ndi Mtumiki (wake)". Koma ngati
Akana, (Mulungu Awakhaulitsa).
Ndithudi, Mulungu sakonda Anthu
osakhulupirira.
33. Ndithudi Mulungu
adasankha Adam ndi Nuh ndi
banja La Ibrahim ndi banja la Imran
pa zolengedwa Zonse (anthu onse).
1 Tsiku lachimaliziro (kiyama) munthu adzalakalaka kuti asawaone machimo
ake amene adachita. Koma kuti machimowo akhale kutali ndi iye pomwe
machimowo akamawachita amakhala wosangalala.
2 Kungonena chabe pakamwa kuti ndikumkonda Mtumiki Muhammad (SAW)
pomwe zochita zako nzosalingana ndimalangizo a Mtumiki Muhammad
(SAW), chikondi chotere chilibe phindu lamtundu uliwonse. Ngati Muhammad
(SAW) tikumkondadi timumvere ndi Kumuyesa chitsanzo chathu pazochita
zathu zonse.
Surat 3. Al-'Imran Juzu 3
115
r *>i
T OIjaP JT ojj-i
34. Ana; ena kuchokera Mwa
ena pakati pawo. Ndipo Mulungu
Ngwakum va, Ngodziwa. l
35. (Kumbukirani) pamene
adanena Mkazi wa Imran (Mayi
wa Mariam (Maria),
M'mapemphero ake): "Mbuye
wanga! Ndapereka Kwa inu
chimene chili m'mimba Mwanga
monga "Wakfu" (wotumikira
M'kachisi Wanu). Tero landirani
Ichi kwa ine. Ndithudi, Inu Ndinu
Akumva, Wodziwa. 2
36. Choncho pamene adam'bala
adati: "Mbuye wanga! Ndabala
wamkazi!" Ndipo Mulungu
akudziwa kwambiri Chimene
wabereka - "Ndipo Wamwamuna
(yemwe ndimayembekezera
Kubala) sali ngati wachikazi
(amene Ndamubala. Sangathe
kutumikira Moyenera mkachisi
wanu). Ndipo ine ndamutcha
Mariam (Wotumikira Mulungu).
1 Ndime iyi ikusonyeza kuti mawere awa ali olumikizana. Ndipo ikusonyeza
kuti anthu abwino ambiri amabala anthu abwino. Tero amene akufuna
kukwatira asankhe nyumba yabwino yachipembedzo, yamaphunziro ndi
yaluso.
2 (Ndime 35-6) Mkazi wa Imran pamene adali ndi pakati, ankaganiza kuti
adzabereka mwana wa mwamuna. Ndipo adalonjeza kwa Mulungu kuti
mwanayo adzampereka kuti akhale wotumikira ku Msikiti wa Baiti Limakadasi
(Yelusalemu), ndi kutinso adzatumikire pazinthu zina zachipembedzo. Ntchito
yake idzangokhala yokhayo. Koma mwatsoka adabereka mwana wamkazi
ndipo kuti adzakhale mwana wabwino nkutinso adzabereke ana abwino.
Adamutcha otumikira Mulungu. Tero mayi Mariam adali mayi wabwino. Ndipo
nayenso adabala mwana wabwino yemwe ndi Mneneri Isa (Yesu). Mariam ndi
mayi wolemekezeka kwabasi.
Surat 3. Al-'Imran Juzu 3
116 r *>»
T ti\y>* JT 5jj--
Ndipo ndikupempha Chitetezo
Chanu Pa iye ndi ana ake kwa
Satana wothamangitsidwayo".
37. Choncho Mbuye wake
adamulandira, Kulandira
kwabwino; namkulitsa, Kukulitsa
kwabwino. Adampatsa Zakariya
kuti amulere. Nthawi Iliyonse
Zakariya akamulowera Mchipinda
mwake (mwa Mariam)
M'kachisimo, amampeza Ali ndi
chakudya. Amati; "I we, Mariam!
ukuzipeza kuti izi?" (Iye) amati:
"Izi zikuchokera kwa Mulungu.
Ndipo Mulungu Amampatsa
yemwe wamfuna popanda
Chiyembekezo (mwini wakeyo)". 1
38. Pompo Zakariya adapempha
Mbuye wake Nati: "Mbuye wanga!
Ndipatseni Kuchokera kwa Inu
mwana wabwino. Ndithudi, Inu
ndinu Akumva pempho!"
39. Mwadzidzidzi, mngelo
adamuitana Uku iye ataimirira
HWA'Zite. -r A»i>['&'S'JSZz
Bambo Imran, tate wake wa Mariam, adali munthu wamkulu mwaanthu
akuluakulu owopa Chauta panthawiyo. Atamubala mwana wakeyu iye
adamwalira. Choncho akuluakulu amene adali naye pamodzi, anapikisana
pankhani yolera Mariam. Kenako adagwirizana kuti achite mayere. Amene
amgwere ndiyemwe alere Mariam. Tero mayerewo adakomera Mneneri Zakariya,
mwamuna wa mayi wake wamng'ono wa mariam. Ndipo Mulungu adamsonyeza
Zakariya zododometsa zambiri kwa mwanayo. Zina mwazododometsa ndiko
kupeza chakudya pamalo pomwe ankakhala mwanayo chomwe chidali
chosadziwika kwa anthu kumene chachokera. Ndipo akamufunsa amati Mulungu
ndiye wampatsa.
2 Mneneri Zakariya ataona zododometsazo, adaganiza kuti nayenso
apemphe kuti amninkhe chozizwitsa chobala mwana pomwe adali wokalamba
zedi. Nayenso mkazi wake adali chumba. Ndipo adamubaladi mneneri
Yahaya (Yohane).
Surat 3. Al-'Imran Juzu 3
117
r *>»
T OIj^p JT hjj^t
akupemphera Mchipinda cha
m'kachisi: "Mulungu akukuuza
nkhani yabwino (Yakuti ubereka
mwana; dzina lake) Yahaya
yemwe adzakhala wotsimikizira
(Mneneri yemwe adzabadwa) ndi
liwu Lochokera kwa Mulungu,
(yemwe ndi Mneneri Yesu) amene
adzakhalanso wolemekezeka ndi
Wolungama ndi mneneri wa mwa
anthu abwino.
40. (Zakariya) adati: "Mbuye
wanga! Ndidzakhala bwanji ndi
mwana Pomwe ukalamba
wandifikira, Nayenso mkazi wanga
nchumba" (Mngelo adati)
"Ndimomwemo; Mulungu
amachita Chimene wafuna."
41. (lye) adati: "Mbuye wanga!
Ndipatseni Chizindikiro!" Adati:
"Chizindikiro chako Ndikuti
sudzatha kulankhula ndi anthu
mpaka Masiku atatu koma
momangolozera (ndi Chala) basi.
Ndipo tamanda Mbuye wako,
Kutamanda kwambiri ndiponso
Umlemekeze (popemphera)
madzulo Ndi m'mawa".
42. Ndipo (kumbukira) pamene
angelo adati: "E I we Mariam!
Ndithudi, Mulungu Wakusankha,
Wakuyeretsa ndipo
Wakulemekeza, mwa Akazi onse
amitundu ya anthu".
®i
Hy*
V/f/ >i'*'
1 Apa patchulidwa nkhani ya mayi Mariam (Maria) pomwe adatha msinkhu ndi
pomwe mngelo adamuuza nkhani yabwinoyi.
Surat 3. Al-'Imran Juzu 3
118
r fjA-i
T Olj-<kP JT 5jj--
43. "E iwe Mariam,
dzichepetse Kwa Mbuye wako ndi
Kumlambira powerama pamodzi
Ndi owerama".
44. Izi ndizina mwankhani
zobisika zomwe
Tikukuvumbulutsira. Sudali nawo
pamene Amaponya zolembera
zawo (m'madzi m'njira Ya
mayere) kuti aone ndani mwaiwo
alere Mariam. Sudali nawo
pamene adali kutsutsana.
45. (Kumbukira) pamene
mngelo adati: "E iwe Mariam
(Maria)! Mulungu akukuuza
nkhani Yabwino (kuti ubereka
mwana popanda Mwamuna Koma
kupyolera mu) liwu lochokera
Kwa lye (Mulungu, lakuti,
"Bereka," ndipo Nkubereka
Popanda kupezana ndi mwamuna).
Dzina lake ndi Mesiya Yesu
mwana wa Mariya, adzakhala
wolemekezeka padziko lapansi ndi
pa Tsiku lachimaliziro; ndiponso
ndi mmodzi wa Oyandikitsidwa
kwa Mulungu.
46. "lye adzayankhula ndi anthu
Ali mchikuta ndi kuukulu (Wake).
Ndipo adzakhala Mmodzi wa
anthu abwino".
47. (Mariam) adati: "Mbuye
wanga! Ndingakhale ndi mwana
Bwanji pomwe sadandikhudze
Munthu aliyense (mwamuna)?"
(A^\>&2&\£&
®£s*w\Z*
Surat 3. Al-'Imran Juzu 3
119
r *>»
T Oij^P JT ojj-*»
© u^c/^0 cl^^^^^l
i^^\SC&\Ki&
" l,? *
(Mngelo) adati: "Ndi Momwemo.
Mulungu Amalenga chimene
wafuna. Akafuna chinthu
amachiuza: "Chitika," ndipo
chimachitikadi.
48. Ndipo Mulungu
adzamphunzitsa Kulemba, nzeru,
Taurat ndi Injili.
49. "Ndipo (adzamchita
kukhala) Mneneri Kwa ana a
Israeli (adzakhala akuwauza kuti):
"Ine ndakudzerani ndizizindikiro
kuchokera Kwa Mbuye wanu kuti
ndikuumbireni dongo Ngati
chithunzi chambalame, nkuuzira
M'menemo nkukhaladi mbalame
Mwachilolezo cha Mulungu;
Ndipo ndichiritsa osapenya
chibadwire, Ndiwamangamaanga,
ndi kuukitsa wakufa Mwa
chilolezo cha Mulungu; ndipo
ndikuuzani Zomwe mudye ndi
zimene musunge m'nyumba
Zanu.Ndithudi, m'zimenezi muli
zizindikiro Kwa inu ngati mulidi
anthu okhulupirira. !
50. "Ndipo (ndikhala)
wotsimikizira zomwe Zidalipo
patsogolo panga (m'Buku la)
Taurat. Ndipo ndadza kuti
ndikulolezeni Zina mwa zomwe
zidaletsedwa kwa inu. Ndipo
1 Apa akunena zina mwazozizwitsa zomwe Mneneri Isa (Yesu) anadza nazo.
Ndipo zina mwaizo ndikuumba ndidongo chifanizo chambalame. Kenako
nkuchiuzira chikhaladi mbalame yamoyo mwachilolezo cha Mulungu.
iKitf'Y' 9&>< 9. 9 9*{s >\Z\\~'9"S
Surat 3. Al-'Imran Juzu 3
120 r*>i.
T OIj^p JT Sjj--
ndakudzerani ndi zizindikiro
Kuchokera kwa Mbuye wanu
(zotsimikizira Uthenga wanga).
Choncho, opani Mulungu ndi
kundimvera (ine).
51. "Ndithu Mulungu ndiye
Mbuye wanga ndiponso Mbuye
Wanu; choncho mupembedzeni.
Iyi ndiyo njira yoongoka".
52. Koma pamene Yesu
adazindikira mwa iwo
Kusakhulupirira adati: "Ndani
akhale athandizi Anga kwa
Mulungu (popitiriza kufalitsa
Chipembedzo Chake)?" Ophunzira
ake Adati: "Ife ndife athandizi a
Mulungu (pofalitsa Chipembedzo
Chake). Takhulupirira Mulungu;
ndipo ikira umboni kuti ife ndithu
Ndi odzipereka (kwa Mulungu).
53. "Mbuye wathu!
Tazikhulupirira Zimene
mwavumbulutsa, Ndipo tamtsata
Mtumikiyo. Choncho tilembeni
pamodzi Ndi oikira umboniwo."
54. Ndipo (Ayuda) adakonza
chiwembu (chofuna Kupha Yesu)
Mulungu adachiwononga
Chiwembu chawocho. Mulungu
ngokhoza bwino zedi Poononga
ziwembu za anthu a chiwembu.
55. (Kumbukirani) pamene
Mulungu adati: "Iwe Yesu! Ine
ndikukwaniritsira nyengo yako
aS32ill5**&l^
Surat 3. Al-'Imran Juzu 3 121 ? ^j** 1
T &\j»& JT ijj«*
Yokhala ndi moyo. (Ayuda sachita
kanthu Kwa iwe). Ndipo
ndikunyamulira kwa Ine
Ndikuyeretsa kwa anthu
osakhulupirira (omwe Ndi adani
ako). Ndipo amene akutsata (Iwe)
Ndiwasankha kukhala apamwamba
pa amene Sadakhulupirire kufikira
tsiku lachimaliziro. Kenako
kobwerera kwanu nkwa Ine, ndipo
Ndidzaweruza pakati panu
pazomwe mudali Kusiyana.
56. Tsono amene
sadakhulupirire, Ndiwakhaulitsa
ndi chilango chaukali padziko
lapansi ndi tsiku lomaliza, ndipo
Sadzapeza athandizi.
57. Koma amene akhulupirira
Nachita zabwino, (Mulungu)
adzawalipira malipiro Awo
(mokwanira). Ndipo Mulungu
Sakonda anthu ochita zoipa.
58. Izi tikukuwerengera iwezi
Ndi zivumbulutso ndi ulaliki
waluntha.
59. Ndithudi, fanizo la Yesu
kwa Mulungu lili ngati fanizo la
Adam; adamulenga ndi dothi
namuuza kuti: "Khala munthu,"
Ndipo adakhaladi. 1
9 k 9 u
©4^
i4$&?£>&)&i
1 (Ndime 59-62) Ndime iyi idavumbulutsidwa pamene nthumwi za chikhirisitu
zidadza kwa mtumlki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) kuchokera ku
Najirani. Iwowo adakangana ndi Mtumiki wa Mulungu pa nkhani ya Yesu. Iwo
adati kwa Mtumiki wa Mulungu "Bwanji iwe ukutukwana Mneneri wathu?" lye
adati: "Kodi ndikutukwana chotani?" Iwo adati: "Iwe ukuti iyeyo ndikapolo wa
Surat 3. Al-'Imran Juzu 3
122
r *>i
T ti\y>* JT Ojj-a
60. (Ichi ndi) choona
chochokera Kwa Mbuye wako;
choncho Usakhale mwaokaikira.
61. Ndipo amene akutsutsana
nawe (Iwe Mtumiki) tsopano pa
ichi Pambuyo pokudzera
kuzindikira, Auze, "Bwerani
tiitane ana athu ndi Ana anu, akazi
athu ndi akazi anu, Ife ndi inu;
kenako modzichepetsa Tipemphe
temberero la Mulungu Kuti likhale
pa amene ali Abodza (Mwa ife)."
62. Ndithu, iyi ndinkhani
yoona; ndipo palibe Woyenera
kupembedzedwa mwa choonadi
Koma Mulungu mmodzi.
Ndithudi, lye Mulungu
Ngwamphamvu Zoposa,
Ngwanzeru zokuya.
63. Ngati atembenuka
(monyoza, Mulungu awakwapula);
&CM$l&'&®)$$$
Mulungu." lye adati: "Inde. lyeyo ndi kapolo wa Mulungu ndiponso mawu ake
omwe adawaponya mwanamwali." Zitatero iwo adapsa mtima ndipo
anakwiya nati, "Kodi iwe udamuonapo munthu wobadwa popanda tate? Ngati
ukunenadi zoona tationetsa munthu wotere." Apa mpomwe Mulungu
adavumbulutsa ndime yakuti "Ndithudi, fanizo la Yesu (Isa) kwa Mulungu lili
ngati fanizo la Adam". Kenako anawaitanira ku Chisilamu. Iwo adati:
"Tidalowa kale m'Chisilamu iwe usanadze." Mtumiki (madalitso ndi mtendere
zikhale naye) adati: "Mwanama. Pali zinthu zitatu zikukuletsani kulowa
m'Chisilamu:
(a) Kunena kwanu mawu oti Mulungu wadzipangira mwana.
(b) Kudya kwanu nyama ya nkhumba.
(c) Kulambira kwanu mtanda."
Pamene adapitiriza kumtsutsa Mneneri Muhammad (madalitso ndi mtendere
zikhale naye) adawapempha kuti atembererane ponena kuti, "O! Ambuye
Mulungu! Mtemberereni ndi kumlanga amene akunena zabodza mwaife pankhani
ya Yesu! Pompo Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) adasonkhanitsa
anthu ake. Koma iwo atakhala upo adagwirizana kuti asalole kuopa kuti
chilango chingawatsikire. Potero zidadziwika kwa anthu kuti iwo ngabodza.
Surat 3. Al-'Imran Juzu 3 123 T *>i
T C)\j+fi> JT *jj*>
Ndithudi Mulungu Ngodziwa za
oononga.
64. Nena: "Inu eni Buku (la
Mulungu, Ayuda Ndi Akhrisitu!)
Idzani kuliwu lolingana Pakati
pathu ndi inu (lakuti) tisapembedze
Aliyense koma Mulungu Mmodzi
Yekha), Ndiponso tisamphatikize
ndi chilichonse; ena Mwa ife
asawasandutse anzawo kukhala
Milungu m'malo mwa Mulungu."
Ngati atembenuka ndi kunyoza,
nenani: "Ikirani umboni kuti ife
ndife Asilamu (Ogonjera
malamulo a Mulungu)."
65. E inu amene mwapatsidwa
Buku! Bwanji mukutsutsana za
Ibrahim pomwe Taurat Ndi Injili
sizidavumbulutsidwe Koma
pambuyo Pake kodi
simuzindikira?
66. Taonani! Inu mudatsutsana
pazomwe Mudazidziwa, nanga
bwanji Mukutsutsana pazomwe
simuzidziwa? Mulungu ndi
Yemwe akudziwa. Pomwe inu
simudziwa.
67. Ibrahim sadali Myuda ndipo
sadali Mkhrisitu, koma adali
wolungama, Wodzipereka; ndipo
sadali Mwa ophatikiza (Mulungu
ndi zinthuzina)
68. Ndithu anthu omwe ali
oyenera Kudzilumikiza ndi
Surat 3. Al-'Imran Juzu 3
124
r *>i
T OI^*p JT Sjj^
M*'-
!><*
Ibrahim ndi amene Adamutsata
(m'nyengo yake) ndi Mtumiki uyu
(Muhammad {SAW}) ndi amene
amkhulupirira (Mtumikiyu). Ndipo
Mulungu ndi Mtetezi wa
okhulupirira.
69. Gulu Una la anthu amene
adapatsidwa Buku likufuna
kukusokeretsani; Ndipo
sasokeretsa aliyense koma Iwo
wokha pomwe (iwo eni)
Sakuzindikira.
70. "E inu amene mwapatsidwa
Buku! Bwanji mukuzikana
Zizindikiro za Mulungu (Qur'ani)
Pomwe mukudziwa?
71. E inu amene mwapatsidwa
Buku! Bwanji mukusakaniza
Choona ndi chabodza, ndipo
Mukubisa choona Uku
mukudziwa?
72. Ndipo gulu lina la amene
adapatsidwa Buku lidati (kwa
anzawo): "Khulupirirani chomwe
Chavumbulutsidwa kwa Asilamu
kumayambiriro Kwa usana, ndipo
chikaneni Kumalekezero kwake
(kwa usana) Mwina angabwerere
(kusiya Chisilamu). 1
1 Ena mwa anthu amabuku adalangizana pakati pawo kuti achikhulupirire
chipembedzo cha Chisilamu nthawi zakummawa zokha. Ikakwana nthawi
yopemphera Swala akapemphere nawo. Koma ikafika nthawi yamadzulo atuluke
m'chipembedzocho ncholinga choti asokoneze Asilamu maganizo, makamaka
omwe adali ofooka pomwe aone kuti anthu anzeru adalowa m'chipembedzocho,
koma kenako atulukamo, nawonso mwina atuluka Poganiza kuti chikadakhala
• iW'.'^S' 9 9 '?*1
Surat 3. Al-'Imran Juzu 3
125 r •>■»
V OIjaP JT ijj^t
73. Ndipo musakhulupirire
aliyense Kupatula yekhayo yemwe
watsata Chipembedzo chanu.
(Mulungu Adauza Mtumiki
{SAW}),nena:"Ndithudi,
chiongoko chenicheni Ndi
chiongoko cha Mulungu basi."
(Amene adapatsidwa Buku
Adanena kwa anzawo:
"Musakhulupirire) kuti
angapatsidwe Aliyense zofanana
ndi zomwe Mwapatsidwa inu
(Ayuda ndi Akhrisitu), kapena kuti
angakutsutseni Kwa Mbuye
wanu." (Mulungu adati Kwa
mtumiki { SAW} ), nena: "Ndithu,
Zabwino zonse zili m'manja mwa
Mulungu; amazipereka kwa
Yemwe wamfuna. Mulungu
Ndimataya, Ngodziwa."
74. Amamsankhira chifundo
Chake amene wamfuna. Ndipo
Mulungu ndimwini Ubwino
wawukulu.
75. Mwa amene adapatsidwa
Buku, Alipo omwe akuti
ukawasungitsa Milumilu yachuma,
akubwezera. Ndipo mwa iwo muli
anthu ena akuti Ukawasungitsa
"dinari" (ndalama) imodzi
Sangakubwezere pokhapokha
Upitirize kwa iye kuimirira
kulonjerera. Izi Nchifukwa chakuti
chipembedzo chenicheni anthu anzeru sakadatulukamo. Izi zidali ndale za
Ayuda zomwe Mulungu adaziulula.
Surat 3. Al-'Imran Juzu 3
126
r *j*-»
y oij^p JT Sjj.*.
amanena: "palibe njira Paife
(yotidzudzulira) chifukwa
chozibera Mbulizi." Koma
akumnamizira Mulungu uku iwo
akudziwa.
76. Sichoncho (monga momwe
akunenera)! Komaamene
akukwaniritsa lonjezo Lake
napewa Machimo (ndiyemwe
Ayenera kukhala Wokondedwa
Kwa Mulungu). Ndithudi,
Mulungu amakonda opewa
machimo.
77. Ndithu anthu amene
akugulitsa chipangano cha
Mulungu ndi malumbiriro awo,
(ndi zinthu za) Mtengo wochepa,
iwo alibe gawo labwino pa Tsiku
lomaliza. Ndipo Mulungu
Sadzawayankhula (ndimawu
abwino); Ndipo sadzawayang'ana
(Ndi diso la chifundo) pa tsiku
Lachimaliziro. Ndiponso
sadzawayeretsa (Kumachimo
awo); ndipo iwo Adzapeza
chilango chopweteka.
78. Ndipo ndithu mwaiwo muli
gulu lomwe likukhotetsa malirime
awo (powerenga) Buku kuti
muaganizire (mawu awowo) Kuti
ndi a m'buku La Mulungu);
pomwe si am' buku (la Mulungu).
Ndipo akunena: "Izi zachokera
kwa Mulungu," Pomwe zimenezo
sizinachokere kwa Mulungu;
&4l&\$$ ufe<^&f <^<J
e^l
Surat 3. Al-'Imran Juzu 3 127 T >>i
T Otj^P JT 5jj-rf
Ndipo akumnamizira Mulungu uku
akudziwa.
79. Sikoyenera kwa munthu
yemwe Mulungu Wampatsa Buku
ndi chiweruzo ndi uneneri, Kenako
nanena kwa anthu: "Khalani
opembedza Ine, mmalo mwa
Mulungu." Koma (awauze):
"Khalani opembedza Mulungu,
anzeru, aluntha chifukwa choti
mukuphunzitsa Buku ndi
Chifukwanso chazomwe
mukuphunzira.
80. Ndipo sangakulamulireni
Kuwasandutsa angelo ndi aneneri
kukhala milungu. Kodi
angakulamulireni Kusakhulupirira
pambuyo Poti muli Asilamu?
81. Ndipo (kumbukirani)
pamene Mulungu adatenga
Lonjezo kwa aneneri,
(n'kuwauza): "Ndikakupatsani
Buku ndi nzeru, nakudzerani
Mtumiki wotsimikizira zomwe zili
pamodzi Ndi inu, nkofunika kwa
inu kumkhulupirira ndi
Kumthangata." (Mulungu)
adatinso: "Kodi mwavomereza ndi
kulandira pazimenezi Pangano
langali? (Iwo) adati:
"Tavomereza". (lye) adati: "Tsono
chitirani umboni, Ine ndili
pamodzi nanu mwa oikira
umboni."
V • 9 $9 9S it 9 9s
C^o «*
fy feM53>i«Ui, O ^~*** Opt)
Surat 3. Al-'Imran Juzu 3 128 ? *j*-»
T OIj^p JT 5jj^
82. Ndipo amene
adzatembenuke Pambuyo pa
lonjezoli, (Mulungu adzawalanga
Chifukwa chakuti) iwo
Ndiopandukiradi chilamulo Cha
Mulungu.
83. Kodi akufuna chipembedzo
Chomwe si cha Mulungu pomwe
Chinthu chilichonse chili
Kumwamba ndipansi chikugonjera
lye, mofuna kapena mosafuna?
Ndipo onse adzabwezedwa kwa
lye.
84. Nena: "Takhulupirira
Mulungu Ndi zomwe
zavumbulutsidwa pa Ife, ndi
zomwe zidavumbulutsidwa Kwa
Ibrahim, ndi Isimail, Isihaka ndi
Yakubu ndi zidzukulu Zake, ndi
Zimene adapatsidwa Musa ndi
Yesu, ndi aneneri (ena) Zochokera
kwa Mbuye wawo. Sitisiyanitsa
aliyense pakati pawo, Ndipo ife
kwa lye ndi Odzipereka
kwathunthu."
85. Ndipo amene angatsate
Chipembedzo chosakhala
Chisilamu, sichidzalandiridwa
Kwa iye. Ndipo lye tsiku Lomaliza
adzakhala mmodzi Mwa (Anthu)
otaika.
86. Kodi Mulungu
angawaongole Bwanji anthu
omwe atuluka M'chikhulupiriro
^^M'i^'*'' 1
>*^j?.
9 1 9
X 99 ' 9 9
U^j^&^4<fl^<il!^
Surat 3. Al-'Imran Juzu 3 129 f *>»
T OIj^p JT djj-»
pambuyo Pakukhulupirira
natsimikiza Kuti Mtumiki (Uyu
Muhammad {SAW}) Ngoona,
nkuwafikiranso zisonyezo
Zoonekera? Koma Mulungu
saongola Anthu ochita zoipa.
87. Iwo mphoto yawo Ndithu
ndi matemberero A Mulungu, a
angelo ndi Anthu onse, ali Pa iwo.
88. M'menemo adzakhala
muyaya; Ndipo
sichidzapeputsidwa Chilango kwa
iwo, Ndiponso sadzapatsidwa
danga.
89. Kupatula anthu amene
alapa, Pambuyo pazimenezo
Nachita zabwino. Ndithudi,
Mulungu Ngokhululuka,
Ngwachisoni.
90. Ndithudi, anthu amene
Atuluka M'chikhulupiriro
pambuyo Pokhulupirira, kenako
Naonjezera kusakhulupirira,
Kulapa kwawo
sikudzavomerezedwa Konse.
Ndipo iwo ndi osokera.
91. Ndithudi amene
sadakhulupirire, Nkumwalira
pamene ali Osakhulupirira,
sikudzalandiridwa Kwa aliyense
wa iwo ngakhale Atapereka dipo
lagolide lodzadza Padziko lonse.
Iwo ndi Omwe adzalandire
®,
'ta
©£$12)^
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4
130
£ >>»
V OIj^p JT Sjj->
chilango Chopweteka, ndipo
sadzakhala Ndi athandizi.
92. Simudzapeza ubwino
(weniweni) kufikira mutapereka
zimene mukuzikonda. Ndipo
chilichonse chimene mupereka,
Ndithudi, Mulungu akuchidziwa.
93. Zakudya zonse zidali
zololedwa Kwa ana a Israeli
kupatula Chimene adadziretsa
Israeli mwini wake Taurat
Isadavumbulutsidwe. Nena:
"Bwerani ndi Tauratiyo ndipo
Iwerengeni ngati mukunena
zoona." 1
94. Ndipo aliyense amene
Adzapekera bodza Mulungu
pambuyo Pa izi iwo Ndiwochita
zoipa.
95. Nena: "Mulungu wanena
zoona. choncho tsatirani
chipembedzo cha Ibrahim yemwe
adali Wolungama; sadali mwa
ophatikiza (Mulungu ndi
mafano)."
96. Ndithudi, Nyumba yoyamba
Yomwe idakhazikitsidwa chifukwa
uJfr
'&£$omi4&$&
Ayuda adauza Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) kuti, "Iwe
sukutsata chikhalidwe cha Ibrahim ngakhale umadzinyenga kuti ukumtsata.
Nanga bwanji ukudya nyama yangamira, pomwe Mneneri Ibrahim sadali kudya
ngamira?" Apa Mulungu akuwatsutsa kuti ngabodza. Ndipo Buku lawo la Taurat
ndilo mboni pabodza lawoli. Atavundukula Buku lawo la Taurat apeza kuti yemwe
adadziletsa kudya ngamira ndi Yakobo, yemwe ankadziwikanso kuti Israeli, osati
Mneneri Ibrahim. Yakobo njemwe adasala kudya nyama yangamira mwachifuniro
chake. Ndipo izi adazichita popanda kukakamizidwa ndi Mulungu.
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4 131 * *>'
T OIj^p JT 5jj^
cha anthu (kuti azipempheramo)
ndiyomwe Hi m'Makka;
yodalitsidwa Ndiponso ndi
chiongolo Kwa anthu onse. 1
97. M'menemo muli zizindikiro
zoonekera (Zozindikiritsa
kupatulika kwake ndi Ukale
wake); ndi pamalo pom we Ibrahim
Adali kuimirira; ndipo amene
akulowamo Amakhala
m'chitetezo; ndipo Mulungu
Walamula anthu kuti akachite Hija
ku Nyumbayo amene angathe
kukonzekera Ulendo wonka
kumeneko. Ndipo Yemwe
angakane, (osapitako Pomwe ali
nazo zomuyenereza), Ndithudi,
Mulungu Ngwachikwanekwane Pa
zolengedwa Zake.
98. Nena: "E inu amene
mudapatsidwa Buku! chifukwa
chiyani Mukuzikana zizindikiro Za
Mulungu pomwe Mulungu ndi
mboni wazonse Zimene
mukuchita?"
99. Nena: " E inu amene
mudapatsidwa Buku! chifukwa
chani mukutsekereza Anthu amene
akhulupirira kuyenda Panjira ya
Mulungu? Mukufuna kuti Ikhote
pomwe inu ndinu mboni (Kuti ndi
s> iMr **K *&'}*
*w&m>
1 Apa akunenetsa kuti nyumba yoyamba kukhazikitsidwa kwa anthu kuti ikhale
yochitira mapemphero ndi Al-Kaaba, osati Baiti Mukadasi monga momwe Ayuda
amakhulupirira.
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4
132 i ►>•
T OIjaP JT ojj»-
• *' 9 fa 9 *)' "" J.f&tt'W " • uTl ' W
njira ya Mulungu Yopanda
choipa)? Komatu Mulungu
Sanyalanyaza zomwe mukuchita."
100. E inu amene
mwakhulupirira! Ngati
muwamvera ena Mwa amene
apatsidwa Buku, akubwezani kuti
Mukhale osakhulupirira Pambuyo
pa chikhulupiriro chanu.
101. Kodi mungakhale
osakhulupirira Bwanji pomwe
ndime za Mulungu
zikuwerengedwa kwa Inu,
pomwenso Mtumiki wake ali
pamodzi nanu? Ndipo amene
Agwiritse mwa Mulungu
(Bwinobwino), ndithudi iye
Wawongoleredwa kunjira
yoongoka.
102. E inu amene
mwakhulupirira! Opani Mulungu;
Kuopa Kwenikweni. Ndipo musafe
Pokhapokha mutakhala Asilamu
(ogonjera). 1
103. Ndipo gwiritsani chingwe
(Chipembedzo) Cha Mulungu
nonsenu, ndipo Musagawikane.
Kumbukirani Mtendere wa
Mulungu womwe Uli painu;
pamene mudali odana Ndipo Iye
1 Pandime iyi akulangiza kuti nthawi iliyonse munthu akhale m'chikhalidwe cha
Chisilamu chokwanira popewa zoletsedwa ndi kumachita zimene alamultdwa
kuchita mmene angathere, chifukwa chakuti munthu sangadziwe nthawi imene
imfa ingamufikire.
*9 <. 9 \'
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4 133 * *>*
V d\y>* JT $jy*
^i#jR&\{&&&®&
S 9 9*is
adalunzanitsa pakati Pamitima
yanu, tero mwamtendere Wake
mudakhala abale; ndipo Mudali
m'mphepete mwa dzenje Lamoto
(wa Jahanama), ndipo lye
Adakupulumutsanimo. Umo ndi
Momwe Mulungu
akukufotokozerani Ma aya Ake
(ndime Zake) kuti muongoke. 1
104. Ndipo mwa inu lipezeke
Gulu la anthu oitanira Kuzabwino
(Chisilamu) Ndipo alamule
(Kuchita) Zabwino ndikuletsa
zoipa. Iwo ndiwo opambana.
105. Ndipo musakhale monga
Aja amene adagawikana Nasiyana
pambuyo Powadzera zisonyezo
Zoonekera poyera (Zowaletsa
kutero). Ndipo Iwo adzakhala
Ndichilango chachikulu.
106. Patsikulo nkhope zina
zidzakhala Zowala pomwe nkhope
zina zidzakhala Zakuda. Tsono
amene nkhope zawo Zidzakhala
zakuda, (adzauzidwa): "Kodi
Mudakana ( Mulungu) pambuyo
Pachikhulupiriro chanu? Choncho,
Lawani chilango (Chopweteka)
Chifukwa cha zomwe mudali
kuzikana."
1 Ndime izi zikuwauza Asilamu onse kuti akhale ogwirizana pamodzi m'dzina
lachipembedzo chawo cha Chisilamu. Asapatukane popatsana maina atsopano
kapena kuti awa akuchokera kudziko lakutilakuti, awa ngamtundu wakutiwakuti.
Kuchita zimenezo nkulakwa kwambiri. Koma pakati pa Asilamu pakhale
chimvano.
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4
134
t *>i
T ti\j+* JT 5jj--
107. Tsono (anthu odala) omwe
nkhope zawo zidzawale, adzakhala
m'chifundo cha Mulungu. Iwo
mmenemo adzakhala muyaya.
108. Awa ndi ma aya (ndime) A
Mulungu; tikukuwerengera
Mwachoonadi. Ndipo Mulungu
Safuna kupondereza Zolengedwa
(zake).
109. Chilichonse cha
kumwamba Ndipansi ncha
Mulungu. Ndipo Zinthu zonse
zidzabwezedwa Kwa Mulungu.
110. Inu (Asilamu) ndinu
mpingo wabwino umene
wasankhidwa kuti uchite zokomera
anthu (onse). Mukulamula
(kuchita) zabwino ndi kuletsa
zoipa, ndipo mukukhulupirira mwa
Mulungu. Ndipo aja adapatsidwa
Buku Akadakhulupirira monga
momwe (Adawalamulira)
kukadakhala kwabwino Kwa iwo.
(Koma) mwa iwo alipo
okhulupirira pomwe ambiri
mwaiwo Ngopandukira
(chilamulo cha Mulungu). 1
111. Sangakuvutitseni (adani
anuwo, Makamaka Ayuda) koma
nditimasautso (tochepa); ngati
(Atayesera) kukuthirani nkhondo,
Akufulatirani (kuthawa); ndipo
Kenako sangapulumutsidwe.
-'Xt 9*\ l» h ??9 9 4'Il S'.Zir'ls
Apa akutchula zifukwa zomwe chipembedzo cha Chisilamu chapambanira
zipembedzo zina. Tero tiyeni tigwirizane ndizimenezi kuti tikhaledi opambana.
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4 135 * *>'
T d\y>* JT 5jj-rf
% 'A
%^\c£\&&\*&
e^l&I^U
112. Adindidwa chidindo
chakunyozeka paliponse pamene
angapezeke kupatula (akagwira)
Chingwe (cha chipembedzo) cha
Mulungu, Kapena chingwe cha
anthu (pothandizidwa Ndi anthu
ena. Koma paokha sangakhale ndi
Nyonga). Abwerera ndi mkwiyo
wa Mulungu; ndipo chidindo
chaumphawi Chadindidwa paiwo.
Izi nchifukwa chakuti Iwo sadali
kukhulupirira mawu a Mulungu,
Ndipo amapha aneneri popanda
choonadi. Izi nchifukwa chakutinso
adanyoza Ndikulumpha malire.
113. Iwo amene adapatsidwa
Buku sali ofanana. Mwa iwo muli
anthu olungama omwe
akuwerenga ma aya (ndime) a
Mulungu nthawi za usiku uku
akumulambira.
114. Amakhulupirira Mulungu
ndi Tsiku lomaliza; ndipo
amalamulira (kuchita) zabwino
ndikuletsa zoipa; ndipo amachita
changu pazinthu zabwino. Ndipo
iwo ndi omwe Ali mwa anthu
abwino.
115. Ndipo chabwino
chilichonse chimene angachite
sadzakanidwa nacho, (koma
adzawalipira malipiro abwino).
Ndipo Mulungu ngodziwa za
amene akuopa lye. 1
1 Apa akunenetsa kuti aliyense amene akuchita zabwino ndicholinga chabwino
ndi kutsata lamulo la Mulungu, adzalipidwa pa zabwino zakezo.
* S9*9" .99>'\\ ' *99 9 rs
®i
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4
136
i *j*-l
T OIj*p JT ijy*
116.Ndithudi, amene
sakhulupirira, chuma chawo
ngakhale ana awo,
sizidzawathandiza chilichonse kwa
Mulungu. Ndipo Iwo ndi anthu
akumoto basi; adzakhala
mmenemo muyaya.
117. Fanizo la chimene
akupereka mwaulere pamoyo uwu
wadziko lapansi, chili ngati
mphepo yomwe mkati mwake muli
chisanu chaukali, chagwera
pamunda wa anthu omwe
adadzichitira okha zoipa,
N'kuonongeratu. Si Mulungu
amene adawachitira zoipa, koma
iwo okha adadzichitira zoipa. 1
118. E inu amene
mwakhulupirira! musawachite
omwe sali mwa inu kukhala
abwenzi; owauza chinsinsi, iwo
sasiya kukuchitirani choipa.
Amakonda zimene
zikukuvutitsani. Chidani chawo
(painu) chaonekera M'milomo
yawo. Ndipo zimene zikubisa
zifuwa zawo, nzazikulu zedi.
Ndithudi, takufotokozerani
zizindikiro zonse ngati inu muli
anthu ozindikira. 2
1 Tsono amene savomereza Mulungu potsatira malamulo ake ndikusiya zomwe
lye adaletsa, ngakhale atachita zabwino zotani sakamlipira pa tsiku lomaliza.
Ngati nkofunika kuti amlipire, ndiye kuti amlipiriratu pompano padziko lapansi.
2 Chimodzi mwa zinthu zazikulu chomwe chimachititsa kuti zochita za anthu
zitheke kapena kuti zilongosoke, ndiko kuzikonza zinthuzo mwachinsinsi. Zioneke
Sural 3. Al-'Imran Juzu 4
137
i *jA-i
T JIjaP JT 5jj--
119. Ha! kodi inu ndinu amene
muwakonda (adani anu) pomwe
iwo sakukondani ngakhale inu
mukukhulupirira mabuku onse?
Akakumana nanu amanena
(mwachiphamaso) :
"Takhulupirira." Koma akakhala
kwaokha, amakulumirani nsonga
za zala chifukwa chaukali. Nena:
"Mwalirani ndiukali wanuwo
ndithudi, Mulungu akudziwa za
m'zifuwa (mwanu)."
120. Ngati chabwino
chikakufikirani, amaipidwa nacho;
koma choipa chikakugwerani
amachikondwerera koma ngati inu
mupirira ndi kuopa Mulungu,
ndale zawo sizingakuvutitseni
chilichonse. Ndithu Mulungu
akudziwa bwino zonse zimene iwo
akuchita. 1
121. (Kumbukira) pamene
unachoka M'mawa kusiya banja
lako kuti uwakonzere Asilamu
malo omenyanira (nkhondo). ndipo
h*'L 'n 9 '\
pamaso pa anthu zili zothaitha kuzikonza. Chifukwa pali anthu ambiri oipa
maganizo omwe safuna kuti zinthu za anzawo zilongosoke. Iwo amafunitsitsa kuti
aziononge zisanachitike. Ndipo nchifukwa chake apa akuletsa kuwaululira
zachinsinsi anthu omwe sali Asilamu, kapena kuwachita kukhala abwenzi enieni.
Komatu sikuti apa akuletsa ubwenzi wakuti, "Muli bwanji? Tin bwino". Ndiponso
sakuletsa kuwachitira zabwino ndi zachilungamo, monga momwe afotokozera
pandime yachisanu nchitatu yam'surat Mumtahina. (Qur'an 60:8)
M'ndime iyi akuwauza kuti asaope ufiti ngakhale kulodzedwa. Koma ayadzamire
kwa Mulungu basi. Chimene Mulungu wafuna chimachitika. Palibe amene
angachitsekereze. Choncho m'bale wanga moyo wako ukhale wokhazikika. Ngati
ufuna kuchita chinthu usaope mfiti, wadumbo ndi mdani. Dziwa kuti chimene
Mulungu walemba sichingafafanizidwe.
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4 138 * *>»
T Jlj^P JT Ojj-*
Mulungu Ngwakumva, Ngodziwa.
122. (Kumbukira) pamene
magulu awiri mwa inu
anafiinitsitsa kuti athawe
(chifukwa cha mantha monga
momwe adathawira achinyengo).
Koma Mulungu adali Mtetezi
wamagulu awiriwo. (Choncho
adawasunga kuti asathawe). Ndipo
asilamu ayadzamire kwa Mulungu
yekha basi.
123. Mulungu
adakupulumutsani pa (nkhondo) ya
Badri pomwe inu munali ofooka
(chifukwa chakuchepa ndi
kusakhala ndi zida zokwanira).
Choncho opani Mulungu kuti
mumthokoze (nthawi zonse
pazomwe akukuchitirani).
124. (Kumbukira) pamene
umauza Asilamu: "Kodi
sizikukukwanirani pokuonjezerani
mbuye wanu zikwi zitatu Za
Angelo otsitsidwa? 2
1 Apa akunena nkhani ya nkhondo yachiwiri yaikulu kwabasi pambiri ya
Chisilamu, nkhondo ya Uhudi. Nkhondo imeneyi Asilamu adalephera kwakukulu
chifukwa cha Asilamu ena amene adaswa lamulo la Mtumiki (madalitso ndi
mtendere zikhale naye). Ndiponso chifukwa cha anthu ena omwe adalowa
Chisilamu mwachiphamaso (Amunafikina), omwe adapita kunkhondo pamodzi ndi
Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) koma adakathawa kunkhondoko.
Ndipo adali ochuluka chigawo chimodzi mwa zigawo zitatu za Asilamu ( V3).
Pothawapo adathawa ochuluka kuposa nambala yatchulidwayi. Koma ena mwa
iwo adabwerera nkudzalumikizananso ndi gulu la nkhondo la Mtumiki (madalitso
ndi mtendere zikhale naye).
2 M'ndime iyi akunena kuti Asilamu pankhondo zawo zolimbana ndi anthu
osakhulupirira Mulungu, adali kuthandizidwa ndi magulumagulu a Angelo.
Angelowo amadza monga anthu ndipo amamenya nkhondo ndi mphamvu
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4
139
t *>i
T OIj^p JT 5jj^»
125. "Inde, ngati mupirira ndi
kudziteteza kumachimo, ndipo
(adani anu) nakudzerani
mwachangu chawo chimenechi
pamenepo Mbuye wanu
adzakuonjezerani ndi zikwi zisanu
za Angelo odziwa kumenya
nkhondo."
126. Ndipo Mulungu sadachite
izi (potumiza angelo) koma kuti
ukhale uthenga wabwino kwainu
ndi kuti pakutero mitima yanu
ikhazikike ndi zimenezo. Ndipo
chithandizo sichichokera (kwa
wina aliyense) koma kwa Mulungu
basi, Wamphamvu zoposa,
Wanzeru zakuya.
127. (Kuchita izi) nkuti adule
gawo la osakhulupirira (kuti ena a
iwo aphedwe) kapena awasambule
ndi kuti abwerere ali olephera. 1
128. Iwe ulibe chako pa izi.
Mwina (Mulungu) angalandire
kulapa kwawo kapena kuwalanga
pakuti iwo ndi anthu oipa.
129. Zonse zakumwamba ndi
zapansi nza Mulungu;
zaumunthu, osati zaungelo. Akadamenya nkhondoyo ndimphamvu yaungelo
ndiye kuti mngelo mmodzi yekha akadawamaliza osakhulupirira onse psiti.
1 (Ndime 127-8) Apa Mulungu akufotokoza zifukwa zomwe adapambanitsira
Asilamu. Ndipo akusonyeza ufumu wake kuti chimene lye wachifuna nchomwe
chingachitike, osati chomwe auje ndi auje akufuna, ngakhale Mtumiki amene.
Ngabodza omwe amati chimene akutiakuti afuna chimachitika, eti chifukwa choti
iwowo ngolungama kwa Mulungu, kapena chifukwa chakuti ngoyera. Izi sizoona.
Surat 3. Al- 4 Imran Juzu 4
140
i *j*-i
V CMjaP JT ijj~*
amamkhululukira amene wamfuna,
ndikumulanga amene wamfuna.
Komatu Mulungu Ngokhululuka
kwambiri, Ngwachisoni.
130, E inu amene
mwakhulupirira! Musadye Riba
(chuma cha katapira),
Kumangoonjezeraonjezera. Ndipo
opani Mulungu Kuti mupambane. 1
131, Ndipo opani moto umene
Wakonzedwa kwa (Anthu)
osakhulupirira.
132, Ndipo mverani Mulungu
Ndi Mtumiki Kuti mumveredwe
chisoni.
133, Ndipo chimkereni
mwachangu chikhululuko Cha
Mbuye wanu (kupyolera m' zochita
zanu Zabwino), ndi Munda (wake)
umene Kutambasuka kwake
(mulifupi) Kuli ngati kumwamba
ndi pansi, Worn we wakonzedwa
kuti Ukhale wa oopa Mulungu. 3
1 Kuipa kwina kwa malonda akatapira (Riba) ndiko kuti amangoonjezeraonjezera
mpaka kuchimaliza chuma chamnzakeyo momchenjerera. Ndipo nchifukwa
chake m'ndime yachiwiriyi ya 131 akunenetsa kuti ngati sasiya machitidwe
akatapira (Riba) ndi kubweza kwa eni zomwe adalandazo, moto wa Jahanama
ukuwadikira.
2 M'ndime iyi akufotokozamo kuti chifundo cha Mulungu sichingapezeke
pokhapokha pomumvera Mulungu ndi Mtumiki wake, potsatira malamulo ake ndi
kupewa zoletsedwa. Munthu sakalowa mumtendere chifukwa choti ndi Msilamu
basi. Kapena chifukwa chakuti amatsata njira yakutiyakuti . Kapena kuti
mtsogoleri yemwe adayambitsa njirayo akakuombola pomwe zochita zake zili
kutali ndimalangizo a Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye). Palibe
angathe kukuombola koma zochita zako zabwino ndizo zidzakuombole.
3 Ndime iyi ikulimbikitsa anthu kuti akangaze kuchita zinthu zowapezetsa chikondi
cha Mulungu.
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4 141 * *>*
T My** JT 6jy*
134. Omwe amapereka
(zopereka Zawo mwaulere)
pamene akupeza bwino Ngakhale
pamene akuvutika; amenenso
Amabisa ukali wawo ndi
okhululukira Anthu. Ndipo
Mulungu Amakonda ochita
zabwino. 1
135. Ndi amene amati akachita
Uve (wamachimo), Kapena
kudzichitira okha zoipa,
Amakumbukira Mulungu
nampempha Chikhululuko pa
machimo awo. Palibe
angakhululuke machimo Koma
Mulungu ndipo Napanda
kupitiriza machimo Omwe achita
uku akudziwa .
136. Iwowo mphoto yawo ndi
Chikhululuko chochokera kwa
Mbuye wawo, Ndi minda yoyenda
mitsinje pansi pake Ndi patsogolo
pake, momwe akakhalamo Mpaka
muyaya. Taonani kukoma malipiro
A ochita zabwino.
137. Zidapita njira za zilango
zambiri Zosiyanasiyana zomwe
adapatsidwa amene Adalipo
patsogolo panu. Tero tayendani
Padziko ndi kuona momwe adalili
mapeto a Anthu otsutsa.
138. Uku ndi kulengeza poyera
kwa anthu (Onse); komanso
{ 9?9 <ty< 9 9> i*4 9 * '? 'C
®c.
\l^Atfiiu£S<3St&i
1 (Ndime 134-5) Ndime izi zikutchula ena mwamakhalidwe omwe munthu
atakhala nawo akalowa kumunda Wamtendere.
Siirat 3. Al-'Imran Juzu 4
142
i tj^\
T d\j+* JT 3jj-*»
chiongoko ndi ulaliki Kwa (anthu)
oopa Mulungu!
139.Ndipo musafooke
(pomenya nkhondo), ndiponso
Musadandaule (ndi mavuto amene
akupezani) Pakuti ndinu
apamwamba, Ngati mulidi
okhulupirira.
140. Ngati mwavulazidwa,
naonso anthuwo Avulazidwanso
molingana. Ndipo masiku
(Amavuto) onga awa timawapatsa
anthu Mosinthanasinthana. (Ichi
chachitika) kuti Mulungu aonetse
poyera amene akhulupirira
(Moona; choncho sadathawe
konse); ndi kuti Awachite ena
mwa inu kukhala Shuhadaa (Ofera
pankhondo yoyera). Komatu
Mulungu Sakonda anthu ochita
zoipa. 1
141. (Izi) nkuti Mulungu
awayeretse Amene akhulupirira
Ndikuwathetseratu osakhulupirira.
142. Kodi mukuganiza kuti
mukalowa Kumunda wamtendere
pomwe Mulungu asadawaonetsere
Poyera amene amenyera
chipembedzo Cha Mulungu
mwainu ndi Kuwaonetseranso
1 M'ndime iyi Mulungu akukumbutsa Asilamu zinthu zosowetsa mtendere zomwe
zidawapeza m'masiku a Uhudi powauza kuti monga iwo adavutitsidwa ndi adani
awo, nawonso adavutitsidwa . Umo ndi momwe zinthu zimachitikira
mosinthasintha. Nthawi zina zigwera awa, kenako zigwera ena, malinga ndi
zochita zawo. Mulungu sakondera.
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4 143 * *>*
V &\j+* JT ijj*t
poyera Opirira (pankhondo ya
Mulungu?) 1
143.Ndithudi, mudali
kuilakalaka Imfa musanakumane
nayo. Ndithudi tsopano mwaiona
(Ndikuphedwa kwa abale anu) Inu
mukupenya. 2
144. Muhammad (SAW) sali
chinthu China koma Mtumiki
chabe. Patsogolo pake adamuka
atumiki Ambiri. Kodi ngati
atamwalira kapena Kuphedwa,
mungabwererenso M'mbuyo,
ndipo amene abwerere M'mbuyo
mwake savutitsa Mulungu ndi
chilichonse; Koma Mulungu
Adzalipira othokoza.
145. Munthu aliyense sangafe
Pokhapokha mwa chilolezo Cha
Mulungu, (ndikukwanira) Nthawi
yake yolembedwa. Ndipo amene
akufuna mphoto Yapadziko
"*s
1 Ndime iyi yikusonyeza chifukwa chomwe Mulungu adalekerera Asilamu kuti
agonjetsedwe pankhondo ya Uhudi.
2 Pamene Asilamu adamva ubwino waukulu umene angaupeze akafera
pankhondoyo monga "Shahidi", aliyense waiwo adakhumba akadafera
pankhondo yoteroyo, kuti akapeze ulemererowo.
Choncho Asilamu makumi asanu ndi awiri (70) adaphedwa pankhondo ya Uhudi
mwa anthu mazana asanu ndi awiri (700) omwe adaima mwamphamvu
kulimbana ndi anthu osakhulupirira omwe adalipo zikwi zitatu (3,000).
3 Apa akunena mwatsatanetsatane kuti Mneneri Muhammad (madalitso ndi
mtendere zikhale naye) ndi mtumiki basi yemwe ndimunthu monga alili anthu ena
onse. Adafa monga momwe ena adafera. Koma ngakhale iye wafa anthu ena
atsanzire chikhalidwe chake ndi zophunzitsa zake zomwe amaphunzitsa.
Asabwerere m'mbuyo poona kuti iye wafa.
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4
144
t *>!
T OIj^p JT 5jj-*»
lapansi, timpatsa Pompo; ndipo
amene akufuna Mphoto ya tsiku
lomaliza tidzampatsa Konko.
Ndithudi, tidzawalipira (Zabwino)
othokoza. ]
146. Ndi Aneneri angati
adamenyana (Ndi adani) pamodzi
ndi anthu Olungama ambiri
komatu sadataye Mtima pamavuto
omwe Adawagwera panjira ya
Mulungu; sadafooke Ndipo
sadagonjere (adani awo) Ndipo
Mulungu amakonda opirira.
147. (Anthu olungamawa)
kunena kwawo sikudali Kwina
koma ankati: "Mbuye wathu!
Tikhululukireni machimo athu ndi
kupyola Malire kwathu m'zinthu
zathu. Ndipo Limbikitsani mapazi
athu (panjira Yanu) Ndipo
tithandizeni ku anthu
osakhulupirira."
148. Choncho Mulungu
adawapatsa mphoto Yapadziko
lapansi ndi mphoto yabwino Ya
tsiku lomaliza. Mulungu amakonda
Ochita zabwino.
149. E inu amene
mwakhulupirira! Ngati
Muwamvere amene
»a
u^^V*^£^'
©
til \JJi\,J Gsy> i £3 l£*-\
\J^ &l\j^\ &£
m<&&&>$&$\
1 Apa akutilimbikitsa kuti tigwire ntchito yodzatipindulira pa tsiku lachiweruziro
molimbika, tsiku lomwe ndilamoyo wosatha.
2 Asilamu akuwauza kuti asataye mtima atawagonjetsa pankhondo iliyonse,
kapena atawapeza masautso amtundu uliwonse. Chofunika nkupirira ndi
kulimbana nawo mavutowo.
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4
145
i *>»
T d\j»e JT i^y*
sadakhulupirire, Akubwezerani
kumbuyo kwanu (Kumachitidwe
achikunja) tero Mudzakhala otaika.
150. Komatu Mulungu ndiye
Mbuye wanu. lye Ngwabwino
kwabasi kuposa Athandizi (ena
onse).
151. Tiponya mantha m'mitima
mwa amene Sadakhulupirire
chifukwa chakumphatikiza
Mulungu (ndi mafano) omwe
Mulungu Sadatsitsire umboni
(wosonyeza umulungu Wawo)
ndipo malo awo adzakhala
kumoto. Taonani kuipitsitsa malo a
anthu ochita zoipa.
152.Ndithudi, Mulungu
adakutsimikizirani Lonjezo lake
(lakuti muwagonjetsa Adani).
Choncho mudali kuwapha
mwachilolezo Chake kufikira
pamene mudafooka ndikuyamba
Kukangana za lamulolo, tero
mudalinyozera Pambuyo
pokuonetsani zimene
mumazikonda; (Pamenepo
mpomwe adasiya kukuthangatani).
Alipo ena mwainu amene
akukonda dziko Lapansi
(zamdziko), ndipo alipo ena
mwainu Amene akukonda tsiku
lomaliza. Kenako (Mulungu)
adakuchotsani paiwo
(adakusiitsani Kuwamenya
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4
146
t *>i
V OI^aP JT 5jj-»
osakhulupirirawo) kuti akuyeseni
Mayeso. Koma lye tsopano
wakukhululukirani. Ndipo
Mulungu ndi mwini kuchita
Zabwino paokhulupirira. 1
153. Kumbukirani pamene
mudali kuthawa Mwaliwiro
popanda kumvera aliyense;
Pomwe Mtumiki adali kukuitanani,
ali Pambuyo panu. Ndipo
(Mulungu) Adakupatsani
madandaulo pamadandaulo.
(Motero wakukhululukirani) Kuti
musadandaule Pazomwe
zakudutsani, ngakhalenso
(Pamasautso) omwe akupezani.
Ndipo Mulungu Ngodziwa Zonse
zimene muchita.
154. Kenako pambuyo
pakudandaula, adakutsitsirani
Mpumulo - tulo tomwe tidaphimba
gulu Lina mwa inu. Padali gulu
"I'll ' 'i\ ' S\" ** *i i i
Apa akulongosola chifukwa chomwe Asilamu adagonjera. Iwo adagonja
chifukwa choswa lamulo la Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) lomwe
adawalamula. Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) adaika paphiri anthu
makumi asanu (50) omwe adali akatswiri olasa mipaliro. Adawauza kuti
asachokepo kuti ateteze gulu la Asilamu kuti adani asawamenye nkhondo
powadzerera kumbuyo. Adanenetsa kwa iwo kuti asachoke pamalopo ngakhale
ataona kuti anzawo akupambana kapena akugonja, kufikira Mtumiki atawalamula
kuti achokepo. Koma ena mwa iwo adanyoza lamuloli pamene adaona kuti
anzawo chammunsi mwaphirilo akupambana ndipo akuthamangitsa adani ndi
kuwapha ndikumatola zotolatola zapankhondo. Choncho, iwo anatsika paphiripo
nkusakanikirana ndi anzawo nayamba kutola nawo zotola zapankhondo.
Mtsogoleri wawo adayesera umu ndi umu kuwaletsa koma sadamumvere
kupatula ochepa okha amene adatsala paphiripo. Pompo ngwazi zina zam'gulu la
adani awowo zitaona kuti anthu omwe adali paphiri achokapo, zidalitembenuza
gulu lawo lankhondo nkuyamba kuwamenya Asilamu chakumbuyo. Potero ambiri
adaphedwa ndi kuvulala.
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4
147
£*>i
T Olj^P JT $jy*
Una lomwe maganizo Awo
adawatangwanitsa (kotero kuti
Amangoziganizira okha)
namuganizira Mulungu Ndi
zoganizira zopanda choonadi,
zoganizira Zaumbuli; ankati: "Ha!
kodi tili ndi chiyani Ife pachinthu
ichi?" Nena: "Zinthu zonse Nza
Mulungu". Akubisa m'mitima
mwawo Zomwe sakuzionetsa kwa
iwe. Akunena: "Tidakakhala ndi
chilichonse pachinthu ichi, Bwenzi
sitikadaphedwa apa". Nena:
"Ngakhale mukadakhala
m'nyumba Zanu, ndithudi kwa iwo
amene imfa idalembedwa (kuti
amwalire) Akadapita kumalo
omwalilirawo, Koma Mulungu
(adachita izi) kuti Awonetse
poyera zomwe zili M'zifuwa zanu.
Ndikuyeretsa Zomwe zili
m'mitima mwanu.Ndipo Mulungu
Ngodziwa za mzifuwa." 1
155. Ndithudi, mwa inu amene
adabwerera M'mbuyo (kuthawa)
tsiku lomwe Magulu awiri a
nkhondo Adakumana (pankhondo
ya Uhudi; gulu la osakhulupilira
Ndi gulu lankhondo la Asilamu),
1 Asilamu atagonjetsedwa choncho, gulu la adani lija lidabwerera kwawo. Koma
ena mwa Asilamu achinyengo omwe adali m'gulu la Asilamu omwe sadathawe
pomwe anzawo amathawa, sadakhulupirire kuti adaniwo abwerera kwawo,
chifukwa choopa; amangoganiza kuti akadalipobe ndipo mwina awathiranso
nkhondo kachiwiri. Tero adadzazidwa mantha m'mitima mwawo ndipo tulo
tidawasowa. Koma Asilamu enieni sadalabadire chilichonse. Amangodya ndi
kugona ngati kuti zopweteka sizinawakhudze.
&#$&.
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4
148
i *>»
T JIj-*p JT 5jj-*»
Satana ndiyemwe adawaterezetsa
Chifukwa cha zina (Zolakwa)
Zomwe adachita; ndipo Mulungu
(Tsopano) wawakhululukira.
Ndithudi, Mulungu Ngokhululuka
Kwambiri, Ngoleza koposa.
156. "E inuamene
mwakhulupirira! Musakhale ngati
amene sadakhulupirire, Nanena za
anzawo pamene Akuyenda
padziko kapena Pomwe
akumenyana nkhondo (Ndikufera
konko) "Akadakhala ndiife
sakadafa, ndiponso
Sakadaphedwa". (Mulungu
adawathira Maganizo amenewa)
kuti iwo akhale Chodandaulitsa
m'mitima mwawo. Komatu
Mulungu ndi amene Amapereka
moyo ndi imfa. Ndipo Mulungu
akuona Zonse zomwe Mukuchita. 1
157. Ndipo ngati mwaphedwa
panjira ya Mulungu, Kapena kufa,
(palibe chotaika kwa inu) Pakuti
chikhululuko ndi mtendere
wochokera Kwa Mulungu
ngwabwino kuposa zomwe
Akuzisonkhanitsa (pamoyo
wapadziko lapansi).
(Ndime 156-7) Apa Asilamu akuwapepesa kuti asaganizire kuti imfayo
yawapeza chifukwa chopita kunkhondo nkuti akadapanda kupitako sakadafa.
Koma akuwauza kuti adafa chifukwa nthawi yawo yamoyo idatha, yomwe
Mulungu adawalembera kuti akhale padziko lapansi. Ndipo ngakhale akadakhala
m'nyumba zawo imfa ikadawapezabe. Ndipo akuwauzanso kuti imfa yofera
kunkhondo yoyera njabwino kuposa yofera pakhomo.
S 9 } • 9 *
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4
149
i *>»
V ti\y>* JT ijj~>
158.Ndipo ngati mumwalira
kapena Kuphedwa,
n'chimodzimodzi, Nonsenu)
mudzasonkhanitsidwa Kwa
Mulungu.
159. Chifukwa cha chifundo
chochokera kwa Mulungu, uli
woleza mtima kwa iwo, (iwe
Mtumiki Muhammad { SAW } ) .
Ndipo Ukadakhala waukali,
wouma mtima, ndithudi,
Akadakuthawa. Choncho
akhululukire ndi Kuwapemphera
Chikhululuko (Kwa Mulungu);
ndipo chita nawo Upo pazinthu.
Ndipo ngati watsimikiza, tsamira
Kwa Mulungu (basi, ndi kuchita
chimene Watsimikiza kuchichita).
Ndithudi, Mulungu Amakonda
oyadzamira kwake (odalira lye).
160. Ngati Mulungu
akupulumutsani, Palibe amene
angathe kukugonjetsani. Ndipo
ngati akulekani, ndaninso
Angakupulumutseni pambuyo
Pokulekani. Choncho, Asilamu
Ayadzamire kwa Mulungu basi.
161. Nkosatheka kwa Mtumiki
Kuchita chinyengo. Ndipo Amene
achite chinyengo adzadza Pa tsiku
lachimaliziro ndi zomwe
Adazichitira chinyengo. Kenako
Munthu aliyense adzalipidwa
(mokwanira) Pazomwe adachita.
Ndipo sadzaponderezedwa.
%Sl&#A$MZ&$
e<3B2hSAai
>•
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4
150
t *>»
T ti\j*& JT 5jj^*
162.Kodi amene akutsata
chokondweretsa Mulungu
angalingane ndi yemwe
Wabwerera ndi mkwiyo
wochokera kwa Mulungu, ndipo
Jahanama nkukhala Malo ake?
Taonani kuipa Kumaio obwerera!
163. Iwo ali ndi maulemerero
(Osiyanasiyana) kwa Mulungu.
Ndipo Mulungu akuona zonse
Zomwe akuchita.
164.Ndithudi, Mulungu
adawachitira ubwino Waukulu
Asilamu powatumizira Mtumiki
Wochokera mwaiwo yemwe
akuwawerengera ma Aya ake
(ndime zake) ndikuwayeretsa
Ndikuwaphunzitsa Buku ndi
(mawu a) nzeru. Ndithudi, kale
adali mkusokera koonekera. 1
165.Pamene sautso
lidakupezani lomwe Inu
mudawathira nalo (adani anu)
Lochulukirapo kawiri, mudanena:
"Lachokera Kuti (sautso) ili?"
Nena: "Ilo lachokera Kwainu eni
(chifukwa chakunyoza lamulo
Lomwe adakuuzani). Ndithudi,
Mulungu Ngokhoza chilichonse."
166. Ndipo sautso lomwe
lidakupezani tsiku Lomwe
Apa Mulungu akukumbutsa Asilamu zachisomo chomwe adawapatsa
pakuwapatsa Mtumiki pomwe Mtumikiyo asanawadzere iwo adali anthu osokera.
Koma kupyolera mwa Mtumikiyo akhala olungama.
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4 151 * *>»
T OIjaP JT 5jj-k
adakumana magulu awiri
ankhondo, Lidali mwachilolezo
cha Mulungu ndi kutinso
Awaonetsere poyera okhulupirira.
167.Ndikuwadziwitsa amene
adachita chiphamaso
(Amunafikina). Iwo adauzidwa:
"Bwerani, Menyani (nkhondo)
panjira ya Mulungu Kapena
mwatsekereze (adani kwa ife)"
Adati: "Tikadadziwa kuti pali
kumenyana, Ndithudi,
tikadakutsatani (koma kumeneko
Kuli kuphedwa kokhakokha basi)."
Iwo Tsiku limenelo adali pafupi
ndikusakhulupirira Kuposa
chikhulupiriro (ngakhale kuti
Masiku onse amasonyeza
Chisilamu mwachiphaMaso).
Akunena ndimilomo yawo zomwe
sizili M'mitima mwawo. Koma
Mulungu akudziwa Bwinobwino
(zonse) zomwe akubisa.
168. Iwo ndi amene adanena za
Abale awo (pomwe iwo) Adakhala
osapita kunkhondo:
"Akadatimvera, sibwenzi
ataphedwa." Nena: "Dzichotsereni
imfa (nokha, kuti Musafe) ngati
mukunenadi zoona."
169. Ndipo musawaganizire
omwe Adaphedwa panjira ya
Mulungu Kuti ndi akufa, koma iwo
Ngamoyo, akudyetsedwa Kwa
Mbuye wawo;
*&£&&&&
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4
152
i *>1
Y" Olj*P JT »}y>
170. Akukondwera pazimene
wawapatsa Mulungu kuchokera
m'zaufulu Zake. Ndipo akufunira
mafuno abwino Amene
sadakumane nawo omwe Ali
pambuyo pawo, (omwe alipobe
Padziko lapansi) ponena kuti pa
iwo Sipadzakhala mantha kapena
kudandaula.
171. Akukondwera chisomo ndi
ubwino Wochokera kwa Mulungu,
Ndi kuti Mulungu sasokoneza
Malipiro a okhulupirira.
172. (A wa ndi) amene
adavomera Mulungu Ndi Mtumiki
pambuyo povulazidwa; Kwa
amene achita zabwino mwaiwo
Ndikuopa Mulungu, adzakhala Ndi
malipiro aakulu. 1
173. Omwenso adaudzidwa ndi
anthu (olembedwa Ganyu ndi
Akafiri aku Makka) kuti: "Anthu
Akusonkhanirani. Choncho
aopeni." Koma (Zonenazo)
zidawaonjezera chikhulupiriro
(Asilamu). Ndipo adati: "Mulungu
akutikwanira, Ndipo lye ndi
mtetezi wabwino koposa."
Asilamu makumi asanu ndi awiri (70) ataphedwa ndi enanso ochuluka
atavulazidwa pankhondo ija ya Uhudi, Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale
naye) adawalamula Asilamu pompo, uku ali ndimabalawo, kuti awatsate adaniwo.
Ndipo adawatsatadi.
Koma adaniwo atamva mphekesera kuti akuwatsata naganiza kuti akutsatidwa
ndi chigulu chankhondo cha Asilamu chachikulu, osati gulu lonlija lomwe
adaligonjetsa. Choncho adaliyatsa liwiro kuthawa. Ndipo Asilamuwo adabwerera
pambuyo poyenda mtunda wautali kuwatsata adaniwo. Tero Mulungu
adawatamanda Asilamuwa pakumvera kwawo kumeneko.
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4
153 t >>>
T &\y>* JT Ijy*
174. Choncho adabwerera
ndichisomo Ndi ubwino
wochokera kwa Mulungu.
Sichidawakhudze choipa
chilichonse; Adatsatira
zokondweretsa Mulungu. Ndipo
Mulungu ndimwini Ubwino
waukulu.
175.Ndithudiuyo
(anakuopsezani) Ndi Satana
yemwe amaopseza anzake.
Choncho musawaope, ndiopeni Ine
ngati inu mulidi okhulupirira.
176. Ndipo asakudandaulitse
omwe Akuthamangira kuchita
zinthu Zachikunja. Ndithu, iwo
Sangapereke sautso lililonse Kwa
Mulungu. Mulungu akufuna Kuti
asawaikire gawo lililonse La
(zabwino) tsiku lomaliza, Ndipo
paiwo padzakhala Chilango
chachikulu.
177.Ndithudi, amene
asinthanitsa Kusakhulupirira ndi
chikhulupiriro, Sangathe
kumvutitsa Mulungu
Ndichilichonse. Ndipo paiwo
padzakhala Chilango chopweteka.
178. Ndipo amene
sadakhulupirire asaganize Kuti
nthawi yaitali imene tikuwapatsayi
Njabwino kwaiwo. Ndithudi,
tikuwapatsa Nthawiyi kuti
aonjezere kuchita Uchimo. Ndipo
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4
154
i *>»
T OI^aP JT ojj«*
paiwo padzakhala Chilango
chosambula.
179.Nkosatheka kwa Mulungu
Kusiya okhulupirira Momwe
mulilimu, mpaka Atalekanitsa
(Pakatipawo) oipaNdi abwino.
Ndipo Nkosatheka kwa Mulungu
Kukudziwitsani zinthu Zamseri,
koma Mulungu Amasankha mwa
Atumiki ake amene wamfuna
(Nkumdziwitsa zina
mwazimenezo). Choncho
khulupirirani Mulungu Ndi
Atumiki ake. Ndipo ngati
Mukhulupirira ndi Kuopa
(Mulungu), Painu padzakhala
malipiro akulu. 1
180. Ndipo asaganize amene
akuchitira Umbombo zimene
Mulungu awapatsa Kuchokera
m'zaufulu Zake kuti kutero
ndibwino Kwa iwo koma kutero
nkoipa Kwa iwo. Adzanjatidwa
magoli Pazomwe adazichitira
umbombo Pa tsiku lachimaliziro.
Ndipo Um'lowam'malo wa
zakumwamba Ndi pansi ngwa
Mulungu. Ndipo Mulungu
akudziwa zonse Zimene
mukuchita.
Pazoopsa ndi pamene pamadziwika Msilamu weniweni. Ndipamenenso
pamadziwikira Msilamu wachinyengo.
2 Apa Mulungu akuchenjeza mbombo kuti zisaone kutsekemera umbombo
wawowo. Chuma akuchichitira umbombocho chidzasanduka njoka zomwe
zidzawazunza kwambiri.
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4 155 * *>»
V Otj^P JT 5jj~a
181.Ndithu Mulungu wamva
liwu (lonyogodola) La omwe
(Ayuda) anena kuti: "Mulungu
Ngosauka, ndipo Ife ndife
olemera." Tazilemba Zimene
anena, ndipo (talembanso) Kupha
kwawo aneneri popanda Choonadi.
Ndipo tidzawauza (Tsiku
lachiweruzo): "Lawani chilango
Chamoto owotcha." 1
182. "Izi nchifukwa cha zomwe
Manja anu adatsogoza. Ndithudi,
Mulungu Sali Opondereza akapolo
ake." 2
183.Amene anenanso:
"Mulungu Adatilamula ife kuti
tisakhulupirire Mtumiki aliyense
mpaka atabwera Ndi nsembe
yopserezedwa ndi Moto." Nena:
"Adakudzerani atumiki
Ndisanadze ndi zisonyezo zooneka
Ndi chimene mukunenachi. Nanga
bwanji Mudawapha, ngati
mukunenadi zoona?" 3
184. Ndipo ngati akutsutsa iwe
(Mtumiki Muhammad {SAW},
1 Ayuda adali kuchitira zamwano Mtumiki akamawalimbikitsa olemera kuti
adzithandiza osauka. Ankati: "Kodi Mulungu wasauka tsopano kuti ife ndife
tidzimdyetsera zolengedwa zake?" Taonani momwe adali kumchitira zamwano
Mulungu!
2 Awa ndi ena mwamawu omwe adzauzidwa akadzaponyedwa kumoto.
3 Ayuda pamene Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) amawauza kuti
amtsate amanena kuti, "Ife sadatilamule kutsata Mtumiki yemwe akuloleza anthu
kumadya sadaka. Koma atilamula kutsata atumiki okhawo omwe akulamula kuti
sadaka zonse azisonkhanitse pamodzi kenako azitenthe ndimoto. Kapena moto
udze kudzapsereza." Zoonadi, atumiki otero adadza koma sadawatsate monga
momwe Mulungu wanenera apa. Komabe sanawalamule kutsata atumiki otero
okhawo. Kutero nkungofuna kupeza chonamizira basi.
'»- > *l ty »{
Siirat 3. Al-'Imran Juzu 4
156
i *>»
T ti\y>e JT 5jj**»
M*$$k'&®&
e.
*jij
sichachilendo) Adatsutsidwanso
atumiki patsogolo pako omwe
Adadza ndi zisonyezo zoonekera
ndi mabuku Anzeru, ndi
mabukunso ounika.
185. Munthu aliyense
adzalawa imfa. Ndithudi,
mudzalipidwa malipiro Anu tsiku
lachimaliziro. Ndipo amene
adzatalikitsidwe ndi moto
Nalowetsedwa ku Munda
Wamtendere, Ndiye kuti
wapambana, (kupambana
Kwakukulu), ndipo moyo uno
wapadziko Lapansi (sulikanthu
koma) Ndichisangalalo chonyenga
basi. 1
186.Ndithu mudzayesedwa
m'chuma Chanu ndi miyoyo yanu;
ndipo mudzamva Masautso ambiri
kuchokera kwa omwe
Adapatsidwa mabuku kale
ndiponso Kuchokera kwa omwe
Akuphatikiza Mulungu (ndi zinthu
Zina; Arab) koma ngati mupirira
Ndi kudzisunga kuzomwe
Mwaletsedwa ndi Mulungu,
(Ndiye kuti mwachita chinthu
chabwino Kwambiri) pakuti zinthu
izi ndi zinthu (Zazikulu) zofunika
munthu Kuikirapo mtima.
187. Ndipo (akumbutse)
pamene Mulungu adamanga
1 Apa anthu akuwauza kuti achite zinthu molimbika zinthu zokawalowetsa
Kumunda Wamtendere ndi kupewa kuchita zinthu, zokawalowetsa kumoto.
Chifukwa anthu akaponyedwa kumoto kupyolera m'zochita zawo zoipa.
J&i^d&j&i&fcJJ
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4
157
i f.jir\ V OIj^p JT 5jj^
Chipangano ndi amene
adapatsidwa Mabuku
(ndikuwauza) kuti ndithudi
Mudzalifotokoze
mwatsatanetsatane (Bukulo) Kwa
anthu, ndipo musadzalibise. Koma
Adaliponya kumbuyo kwa Misana
yawo Naligulitsa ndi mtengo
wochepa. Taonani kuipa Chimene
adagula (chimene adasankha)!
188. Musaganize kuti amene
akukondwera Zinthu (zoipa)
zomwe achita nakonda
Kutamandidwa ndi zomwe
sadachite, Musawaganizire kuti
akapulumuka Kuchilango. (Koma
kuti) paiwo Padzakhala chilango
chopweteka.
189. Ndipo ufumu
wakumwamba Ndi pansi ngwa
Mulungu; Ndipo Mulungu
ngokhoza Chilichonse.
190. Ndithudi, mkalengedwe
Kakumwamba ndi Dziko lapansi
ndi Kusinthana kwa usiku Ndi
usana, muli zisonyezo Kwa eni
nzeru,
191. Omwe amakumbukira
Mulungu, AH chiimire ali
chikhalire, Ndi ali chigonere
chamnthiti Mwawo; amalingalira
kalengedwe Ka thambo ndi nthaka
(m'mene Mulungu adazilengera,
uku akuti): "Mbuye wathu!
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4 158 * *>» 1" 0^ JT Sj^
simunalenge Izi mwachabe.
Ulemerero ngwanu. Tichinjirizeni
kuchilango chamoto."
192. "E Mbuye wathu!
Ndithudi, Yemwe
mudzamulowetse kumoto Ndiye
kuti mwamuyalutsa, ndipo
Sipadzakhala athandizi Kwa ochita
zoipa."
193. "Mbuye wathu"! Ndithudi,
Ife tamva woitana Akuitanira ku
Chikhulupiriro kuti, "Khulupirirani
Mbuye wanu", ndipo
Takhulupirira. E Mbuye Wathu!
Tikhululukireni machimo athu ndi
Kutifafanizira zoipa zathu, ndipo
mutenge Mizimu yathu tili
pamodzi Ndi anthu abwino.
194. E! Mbuye wathu!
Tipatseni Zimene mudatilonjeza
Kupyolera mwa atumiki anu Ndipo
musazatisambule tsiku
lachimaliziro. Ndithudi, inu
simuswa lonjezo.
195. Choncho Mbuye wawo
adawavomereza (Zopempha zawo
ponena kuti): "Ndithudi, Ine
Sindidzasokoneza khama
(lantchito yabwino) Kwa ochita
khama mwainu, kaya atakhala
Mwamuna Kapena mkazi, (pakuti)
inu ndinu Amodzi. Choncho
amene asamuka (kumidzi Yawo
mwachifuniro chawo),
-7
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4 159 * *>»
Y d\ytS> JT 8jj-u
naapirikitsidwa Midzi yawo
navutitsidwa panjira yanga,
Namenya (nkhondo) ndikuphedwa,
Ndithudi, ndiwafafanizira zolakwa
Zawo. Ndipo ndidzawalowetsa
M'minda yomwe pansi pake ndi
patsogolo Mitsinje ikuyenda.
Amenewo ndimalipiro Ochokera
kwa Mulungu, ndipo kwa
Mulungu kuli malipiro abwino."
196.Ndithu, kusakunyenge
Kuyendayenda padziko Kwa
amene sadakhulupirire.
197.Ndichisangalalo chochepa;
Kenako malo awo ndikumoto Wa
Jahanama. Taonani kuipa kwa
Malo okhazikika.
198. Koma amene aopa Mbuye
wawo Potsatira zolamulidwa ndi
kuleka Zoletsedwa adzapeza
minda yamtendere Momwe
mitsinje ikuyenda pansi ndi
patsogolo Pake. Adzakhala
m'menemo muyaya, Ndi phwando
lochokera kwa Mulungu. Ndipo
zomwe zili kwaMulungu nzabwino
Kwa anthu abwino (kuposa
Zosangalatsa zadziko lapansi).
199, Ndithudi mwa amene
adapatsidwa Buku, alipo Amene
akukhulupirira Mulungu ndi
zimene Zavumbulutsidwa kwa inu,
ndi zimene Zidavumbulutsidwa
kwa iwo, uku Akuzichepetsa kwa
^u^&ty^i^
©
"k\i
vl/w
5?
Surat 3. Al-'Imran Juzu 4 160 * *>*
V OIj^p JT 3jj-g
Mulungu; sagulitsa ndime Za
Mulungu ndi mtengo wochepa
(wapadziko Lapansi). Iwo
adzalandira malipiro awo kwa
Mbuye wawo. Ndithudi, Mulungu
Ngwachangu pakuwerengera.
200. E inu amene
mwakhulupirira! Pirirani, ndipo
Agonjetseni adani anu
ndikupirirako; ndipo Tetezani
malire anu ndipo muopeni
Mulungu kuti Mukhale opambana.
i>9 *" * V^f'^f 'F\ *lL*f , l~f*'"£
\3J&3$J?o\ &\Q$\$$&
hi^j&MjfrftM
'ua
Surat 4. An-Nisa' Juzu 4 161 t *>t
t *L*Jl 5jj-*»
Surat An-Nisa' IV
" " ."" """ '" . r^-
mm .
M'dzina la Mulungu waChifundo
Chambiri, waChisoni.
1. E inu anthu! Opani Mbuye
wanu yemwe Adakulengani
kuchokera mwa munthu Mmodzi
(Adam) ndipo adalenga mmenemo
Mkazi wake (Hawa), ndipo
adafalitsa amuna ndi Akazi ambiri
kuchokera mwa awiriwo. Ndipo
opani Mulungu yemwe kupyolera
Mwa lye mumapemphana. Ndipo
(sungani) chibale. Ndithudi
Mulungu ndimyang'aniri pa inu
(Akuona chilichonse chimene
muchita). 1
2. Ndipo apatseni ana amasiye
chuma chawo; Musasinthanitse
choipa ndi chabwino. (Musasankhe
choletsedwa); ndipo musadye
Chuma chawo pochiphatikiza ndi
chuma chanu. Ndithudi, (zonsezo)
ndiuchimo waukulu.
o&£\<£&\&\j
Ndime iyi ikulimbikitsa zakuopa Mulungu ndi kumulemekeza potsatira
malamulo ake ndi kupewa zomwe lye waletsa. lye ndi amene adakulenga.
Ndiyemwenso adalenga zonsezimene iwe adakulengera. Ngakhale iwe
amene utafuna chithandizo kwa anzako umampempha ponena kuti
"Ndikukupempha m'dzina la Mulungu kuti undichitire chakuti." Izi umachita
poona kuti iye adzalemekeza dzina la Mulungu, ndipo adzakwaniritsa chomwe
ukufunacho. Koma nanga bwanji ukuchita zimene Mulungu waletsa? Bwanji
sukulemekeza lamulo lake pomwe iwe ukufuna kuti anthu achite zomwe
sukuchita. Apa akutiuzanso kuti Mulungu akuona chilichonse chimene anthu
ake akuchita, ngakhale chikhale chochepa chotani.
Surat4. An-Nisa 9 Juzu 4
162
t *>t
t *L-jJt *JJ-"
3. Ngati mwaopa kuti
simungachite chilungamo Pa
amasiye (opaninso kusawachitira
Chilungamo akazi pamitala),
choncho Kwatirani amene
mukuwafuna mwa akazi; Awiri,
kapena atatu, kapena anayi (basi).
Koma ngati mukuopa kuti
simungathe kuchita Chilungamo,
(kwatirani) mmodzi basi kapena
Amene manja anu akumanja
adapeza (mdzakazi). Kutero
kudzakuchititsani kuti
musapendekere (Kumbali
yosalungama). 1
1 Maulama onse a Malamulo a Chisilamu adamvana kuti ndime iyi yaika
malire amitala yomwe munthu akhoza kukwatira. Ndipo ikuletsa kukwatira
akazi opyola anayi panthawi imodzi. Naonso mahadisi a Mtumiki (madalitso
ndi mtendere zikhale naye) akuthirira ndemanga nkhani yokhayokhayi.
Kwanenedwa kuti "Ghayilan", mkulu wina waku Taif adali ndi akazi asanu ndi
anayi (9). Ndipo pamene analowa m'Chisilamu mtumiki anamuuza kuti atsale
ndi akazi anayi okha. Enawo awasudzule. Ndipo palinso nkhani ya Naufali
Bun Muawiya yemwe atalowa m'Chisilamu Mtumiki adamulamula kuti pa
akazi ake asanu asudzulepo mmodzi kuti atsale ndi anayi, Koma ngakhale zili
choncho pafunika kuiganizira mozama ndime imeneyi pamene ikumloleza
munthu kukwatira akazi opyolera mmodzi. Nkofunika kuti akazi onsewo
awachitire zachilungamo powagawira zofuna zawo mofanana popanda
kukondera aliyense waiwo. Tero, munthu akachita chilolezochi mwachabe
nakwatira mitala popanda kuchita chilungamo pakati pawo ndiye kuti
akuchitira Mulungu chinyengo. Pachifukwa ichi, mabwalo a Chisilamu
ozengera milandu apatsidwa mphamvu yokakamizira anthu kuti achite
chilungamo pamitala kuti chomwe mkazi sadamchitire, amchitire. Koma
ngakhale zili choncho ndikulakwa kwakukulu kuganizira kuti chilungamo
chomwe chaikidwacho chikuchotsa chilolezo chokwatira mitala. Umo
simmene Qur'an ikunenera, iyayi. Asilamu omwe ali ndimaganizo amenewa
ndiomwe amira m'maganizo a Akhrisitu a ku Zambwe. Asilamuwa amati
"Nayonso Qur'an ikuletsa kukwatira mitala. Koma kuti siinachotse
mwamtheradi lamulo lakukwatira mitala chifukwa chakuti idaona kuti chidali
chinthu chanzeru kutero panthawiyo poti chizolowezi chamitalachi chidafala
ponseponse. Tero, mmalo mwake idaloleza anthu kukwatira mitala ngati
angawachitire akazi awowo zachilungamo. Tsono poti chilungamochi nkovuta
kuchikwaniritsa pamitala, chimene chilipo apa nkuti pasakhale mitala."
Surat4. An-Nisa' Juzu 4
163
£ *>i
t *L*Jl Sjj-**
4. Ndipo akazi apatseni mahari
Awo (chiwongo) monga mphatso.
Koma (akazi anuwo) ngati
Atakupatsani mokoma mtima
Chilichonse (M'chiwongocho),
Idyani mokondwa ndi
Mothandizika nacho. 1
5. Ozerezeka musawapatse
chuma chanu Chomwe Mulungu
wachichita kukhala Cholimbitsa
matupi anu ndi moyo wanu. Koma
adyetseni nacho ndikuwaveka
nacho Ndikuwauza mawu abwino
(Monga kuti: Mukadzakula
Ndikukhala olungama,
Tidzakupatsani chuma chanu). 2
Ndithudi, maganizo amenewa ngodabwitsa poona momwe Asilamu ena
akugonjera zonena za Akhrisitu. Chifukwatu kukwatira mitala sichinthu choipa.
Mwina kutero kungakhale kofunika zedi kwa anthu ena kuti kuwaletse
kulumpha malire a Mulungu. Pali anthu ena amene ali ndi mphamvu zambiri
zachibadwa omwe sangakhutitsidwe kukhala ndimkazi mmodzi. Chilolezo
chokwatira mitala mpaka kulekeza pa akazi anayi chimawapewetsa anthu
monga awa kumachitidwe achiwerewere. Qur'an ikuloleza anthu monga
amenewa kukwatira mitala ngati angachite chilungamo. Koma amene akuti
kukwatira mitala nkoipa, akufuna kungotsutsana ndi Qur'an.
1 Kumuitanitsa chiwongo mkazi wako chimene udampatsa kapena kumlipitsa
ndalama iliyonse, zotere nzosaloledwa.Koma ngati iye mwini atakugawira
mokoma mtima kachinthu kam'chiwongocho landira usamkanire. Monga iwe
umampatsa, iyenso akhoza kukupatsa.
2 Ayang'aniri a ana amasiye, monga momwe awauzira kuti asawachenjerere
ana amasiye koma kuti awapatse chuma chawo mokwanira, apa
akuwauzanso kuti apitirize kuyang'anira chuma cha ana amasiyewo.
Asawapatse pomwe sali ozindikira zinthu, ali ofooka m'maganizo pomwe
sakuzindikira kufunika kwachuma kuopa kuti angaononge chumacho
mosalongosoka. Tero asawapatse ngakhale misinkhu yawo ili yaikulu. Koma
apitirize kuwasungira chumacho ndi kumawauza mawu abwino ponena kuti
"Mpaka pano ndikuona kuti mwanokha simungathe kuchiyendetsa bwino
chuma chanu. Tero ndiloleni ndikusungirenibe mpaka nthawi yochepa
kutsogoloku. Ndikadzaona kuti nzeru zakhazikika apo mpomwe
ndidzakupatsani chumachi. Chifukwa chakuti chuma chamwana wamasiye
chitaonongeka, kulakwa kwake sikudzakhala kwa wamasiye yekhayo. Koma
Surat4. An-Nisa'
Juzu 4
164
i tj*-i
t *l*Ji djj-**
6. Ayeseni amasiye
(akayandikira kukula Msinkhu kuti
muone kuti atha kuchita ntchito
Yabwino ndi chuma chawo
mukawapatsa) Kufikira atafika
nthawi yokwatira/kukwatiwa.
Ndipo ngati mutawaona kuti ali
ndi nzeru zabwino, Apatseni
chuma chawo. Musachidye
mosasamala Ndi mwachangu
poopa kuti angakule. Ndipo
Amene ali opeza bwino adziletse
(kulandira Mphoto yolerera ana
amasiyewo). Koma amene Ali
wosauka adye mwaubwino (osati
Moononga). Ndipo pamene
mukuwapatsa chuma Chawo,
funani mboni (zoonerera
kuperekedwa Kwa chumacho).
Ndipo Mulungu ali Wokwana
Kukhala Muwelengeri (ndi
Woyang'anira). 1
7. Amuna m ' chuma chimene
makolo ndi achibale Asiya ali ndi
gawo. Naonso akazi ali ndigawo
M' chuma chimene asiya makolo
ndi achibale (Chapafupi), ngakhale
chitakhala chochepa Kapena
chochuluka ndigawo Logawidwa
(ndi Mulungu).
kudzakhudzanso munthu wosungawe. Chumatu ndicho chinthu chokonzera
zinthu zambiri, zabwino. Tero nkofunika kuti chisamalidwe.
1 Komatu akhale akumuyesayesa wamasiyeyo pomusiira kuti nthawi zina
aziyendetsapo yekha chumacho kuti aphunzire kasamalidwe kake. Akaona
kuti akukhoza, ampatse Asamachedwetsere mwadala.
2 Apa tsopano akufotokoza mmene chuma chamasiye angachigawire ponena
kuti m'Chisilamu akazi akuwalola kuwagawirako chuma cha abale awo, osati
Surat4. An-Nisa' Juzu 4
165
t *>t
t 5-L-Jl 5jj-»»
8. Ndipo panthawi yogawa
Akadza achibale, amasiye Ndi
osauka (omwe alibe Gawo
pachumacho), apatseniko Kanthu
ndi kunena nawo mawu abwino. 1
9. Ndipo (wowasiirawo) aope
kuchenjerera Amasiye, kuti naonso
ngati atasiya ana awo Ofooka
pambuyo, akadawaopera (kutaika).
Choncho aope Mulungu ndipo
anene mawu Olingana (kwa ana
amasiye wo).
10. Ndithu, amene akudya
chuma cha Ana amasiye
Mopondereza, Akudya ndi kuthira
moto M'mimba zawo. Ndipo
Adzalowa kumoto woyaka!
11. Mulungu akukulamulani za
ana anu achimuna Apate gawo
lolingana ndi gawo la akazi Awiri.
Ngati akaziwo ali (opitirira) awiri,
Ndiye kuti adzalandira Zigawo
kuti amuna okha ndiwo, owagawira. Koma gawo lomwe mkazi amapatsidwa
limacheperapo poyerekeza ndi gawo lomwe mwamuna amalandira. Chifukwa
chakuti mwamuna ndiye ali ndi udindo waukulu poyerekeza ndi mkazi.
Mwamuna ali ndi udindo woyang'anira mkazi wake, ana ake ndi makolo ake.
Koma mkazi alibe udindo woyang'anira mwamuna wake. Ndiponso alibe
udindo woyang'anira mwana kapena makolo ake, pokhapokha ngati tate wa
anawo ali wochepa nzeru. Zikatero mpomwe mkaziyo amakhala ndi udindo
woyang'anira ana ake. Ndipo udindo wamkazi poyang'anira makolo ake uli
wochepa (theka) poyerekeza ndi mlongo wake.
1 Chuma nchinthu chimene chimachotsa moyo wamunthu mmalomwake,
makamaka ngati chikupezeka m'njira yaulere yosachivutikira, monga chilili
chuma chamasiye. Choncho amene alibepo gawo pachumacho amangoti diso
tong'o, kusirira. Ndipo nchifukwa chake Mulungu apa akunena kuti pogawa
chuma chamasiyecho ngati achibale atabwerapo omwe alibepo gawo
pachumacho, awapatseko kachinthu kochepa ndi kuwapepesa kuti chomwe
awapatsacho nchochepa.
Surat4. An-Nisa'
Juzu 4
166
i frjJrl
t ^L— ui ^JJ- 4
ziwiri mwazigawo zitatu (%) za
(Chumacho) chimene wasiya
(womwalira), Ngati Mwana
wamkazi ndi mmodzi, apatsidwe
Chigawo chimodzi mwa zigawo
ziwiri (Y 2 ) Naonso makolo ake
awiri aliyense waiwo Alandile
chigawo chimodzi mwazigawo
zisanu Ndi chimodzi (V 6 )
chachuma chosiidwacho, ngati
(Womwalirayo) wasiya mwana
(kapena Mdzukulu). Koma ngati
sadasiye mwana, ndipo Makolo
ake awiri ndiwo awasiira, ndiye
kuti Mayi wake alandire chigawo
chimodzi Mwazigawo zitatu QA)
chachumacho, (ndipo Bambo
alandire ( 2 A). Ngati wakufayo
wasiya Abale, ndiye kuti mayi
Wake apeza chigawo chimodzi
mwazigawo Zisanu ndi chimodzi
(V 6 ) chachumacho. (Kugawa
Chumaku kuchitike) atachotsapo
chimene iye Adalamulira kuti
adzachipereke kwakutikwakuti,
Kapena kulipira ngongole (zake).
Atate anu ndi Ana anu, simudziwa
inu kuti ndani mwaiwo Amene ali
ndi chithandizo chapafupi kwainu.
Amenewa ndi malamulo omwe
akhazikitsidwa Ndi Mulungu.
Ndithudi, Mulungu Ngodziwa
Kwambiri, Ngwanzeru zakuya. 1
1 Apa akufotokoza zakagawidwe kachuma chamasiye (mirath).
a) Ngati munthu wamwalira nkusiya, ana amuna ndi akazi tero mwana
wamwamuna adzapeza magawo awiri ndipo wamkazi adzapeza gawo limodzi.
Siirat4. An-Nisa' Juzu 4
167
i *>»
t tL— Jl $jj-*»
12. Inunso mupata chigawo
chimodzi mwazigawo Ziwiri (Vi)
chachuma chimene akazi anu
Asiya ngati alibe mwana (kapena
mdzukulu) ngati asiya Mwana
ndiye kuti inu mupata chigawo
chimodzi M'zigawo zinayi ( V4)
chachuma chosiidwacho
Mutachotsapo zomwe adalamula
kuti zipite Kwakutikwakuti kapena
ngongole zake, Naonso akazi anu
b) Munthu akafa nkusiya ana akazi okha, awiri kapena ochulukirapo, anawo
adzatenga magawo awiri achumacho. Ndipo onsewo alandire
mofanana.Pasapezeke wotenga zochuluka kuposa wina.
Tsono gawo lomwe latsala lidzaperekedwa kwa ena oti awagawire ngati alipo.
Ngati palibe, ndiye kuti gawolo lidzaperekedwanso kwa ana akaziwo.
N.BH Magawo awiri m'magawo atatu C 2 ^), apa akutanthauza kuti chuma
chonsecho amachigawa m'magawo atatu ofanana. Ndipo akaziwo nkulandira
magawo awiri mwamagawo atatuwo.
c) Ngati munthu atamwalira nkusiya mwana mmodzi wamkazi, ndiye kuti
chumacho achigawe magawo awiri ofanana. Gawo limodzi mwamagawo awiri
aja alipereke kwamwana wamkaziyo. Ndipo gawo lotsalalo alipereke kwa ena
ofunika kuwagawira ngati alipo. Ngati palibe, aliperekenso kwa mwana
yemweyo. Lamulo la adzukulu likufanana ndilamulo la ana ngati wakufayo
adalibe ana koma adzukulu ake okha.
d) Munthu akafa nkusiya ana ndi makolo ake, (tate ndi mayi), tero tate
adzapeza gawo limodzi mwamagawo asanu ndi limodzi (v 6 ) a chumacho.
Nayenso mayi adzapeza gawo limodzi mwa magawo asanu ndi limodzi (7*).
Ndipo chuma chotsaliracho adzalandira ndi ana kapena adzukulu amuntnu
wakufayo.
e) Munthu akafa nkusiya tate wake ndi mayi wake basi, popanda ana ndi
adzukulu choncho apa mayi adzalandira gawo limodzi mwamagawo atatu
achumacho. Ndipo tate adzatenga magawo awiri.
f) Munthu akafa nkusiya mayi wake yekha ndi abale ake obadwa nawo kwa
mayi ndi bambo mmodzi, kapena akumbali yakwabambo okha kapena
akumbali yamayi okha, apa mayi adzalandira gawo limodzi mwamagawo
asanu ndi limodzi achumacho. Anthu oyenera kuwagawira chuma chamasiye
asawagawire msanga chumacho mpaka ngongole zonse zawakufayo
atazibweza. Ndiponso mpaka apereke chilawo (wasiya) chomwe wakufayo
adanena kuti chidzachitike. Owagawira chumawo asakhale anthu osusuka
ndichumacho. Choyamba aonetsetse kuti izi zonse zakwaniritsidwa. Komatu
chilawocho chisapyole pagawo limodzi mwamagawo atatu (73) achumacho.
Chikapyolera pamenepa ndiye kuti choonjezerapocho sichivomerezedwa.
Surat 4. An-Nisa'
Juzu 4
168 i *>»
t s-L-jJl 3jj~*»
apata chigawo chimodzi
M'zingawo zinayi ( V4) pachuma
chomwe Mwasiya, ngati mulibe
mwana (ndi mdzukulu). Koma
ngati mwasiya mwana (ndi
mdzukulu), (Akaziwo) apata
chigawo chimodzi m'zigawo
Zisanu ndi zitatu ( vg) pachuma
chomwe mwasiya Mutachotsapo
chomwe mudanena kuti chipite
Kwakutikwakuti kapena kulipira
ngongole (Zanu), Ngati mwamuna
kapena mkazi Olowedwa m'malo
pachuma pomwe alibe Mwana (ndi
mdzukulu) ngakhale makolo awiri,
Koma ali naye m'bale wake
(wakuchikazi) kapena Mlongo
wake (wakuchikazinso) aliyense
Waiwo apata chigawo chimodzi
m'zigawo Zisanu ndi chimodzi
(V5). Ndipo ngati ali
Ochulukirapo, ndiye kuti
agawirana chigawo Chimodzi
m'zigawo zitatu ( V3) cha
chumacho Pambuyo pochotsapo
chomwe chidanenedwa kuti
Chipita kwakutikwakuti kapena
kulipira ngongole, Popanda
kupereka mavuto. Awa ndi
malamulo Ofunika omwe achokera
kwa Mulungu. Ndipo Mulungu
Ngodziwa kwambiri (pokhazikitsa
Malamulo); Woleza (pa akapolo
ake). 1
1 Apa akufotokoza mmene anthu ena angawagawireko chuma chamasiye.
a) Ngati atafa mkazi nkusiya mwamuna wake yekha popanda kusiya ana
Surat4. An-Nisa'
Juzu 4
169
t *>»
£ s-L-Jl 5jj**»
13. Amenewo ndiwo malire a
Mulungu; (Musawalumphe).
Ndipo amene angamvere Mulungu
ndi Mtumiki Wake
adzamulowetsa M'minda yomwe
pansi ndi patsogolo pake Mitsinje
ikuyenda. Adzakhala m'menemo
Muyaya. Kumeneko ndiko
kupambana Kwakukulu.
14. Koma amene anganyoze
Mulungu ndi Mtumiki wake, ndi
kulumpha Malire ake, (Mulungu)
adzamulowetsa Kumoto;
nadzakhala m'menemo Muyaya.
kapena adzukulu, mwamunayo alandire gawo limodzi mwamagawo awiri
achuma ( ^l^ chomwe wasiya mkazi wakecho.
b) Akafa mkazi nkusiya mwamuna ndi mwana wake kapena mdzukulu wake
apa ndiye kuti mwamunayo adzalandira (7 4 ) chigawochimodzi mwazigawo
zinayi zachumacho.
c) Akafa mwamuna nkusiya mkazi wake popanda mwana kapena mdzukulu
wake ndiye kuti mkaziyo adzalandira (7 4 ) chigawo chimodzi mwazigawo
zinayi zachuma chamwamuna wakecho. Ndipo chotsalacho achipereke kwa
ena ofunika kuwagawira.
d) Akafa mwamuna nkusiya mkazi wake ndi mwana wake kapena mdzukulu
wake, apa mkazi alandire ( 1 /q) chigawo chimodzi mwazigawo zisanu ndi
zitatu zachuma chamwamunayo.
e) Akamwalira munthu popanda kusiya ana kapena zidzukulu ndi makolo,
koma nkusiya mbale mmodzi wamwamuna kapena wamkazi wakumbali
yamayi, apa ndiye kuti mbaleyo adzalandira ( 1 /g) gawo limodzi mwamagawo
asanu ndi limodzi achumacho. Ndipo chotsalacho adzawagawira ena oyenera
kuwagawira ngati alipo. Koma ngati palibe ndiye kuti mbaleyo adzatenganso
chotsalacho.
f) Akamwalira munthu popanda kusiya ana kapena adzukulu ndi makolo,
koma wasiya abale akumbali yamayi, amuna kapena akazi, apa ndiye kuti
abalewa adzalandira (V3) gawo limodzi mwamagawo atatu achuma
chawomwalirayo. Ndipo adzagawana pakati pawo mofanana amuna ndi akazi
omwe.
Surat4. An-Nisa'
Juzu 4
170
t *>i
£ tL-Jl djj^
Ndipo adzapeza Chilango
chosambula.
15. Ndipo omwe achite chauve
(chigololo) mwa Akazi anu,
afunireni mboni zinayi za mwainu
Zoikira umboni paiwo. Ngati
ataikira umboni (Kuti achitadi
chauvecho), atsekereni M'nyumba
kufikira imfa idzawapeze, kapena
Mulungu adzawaikire njira ina
(monga Kuphedwa). 1
16. Ndipo amuna awiri mwainu
amene akuchita Zauve (monga
kuchitana ukwati amuna Okhaokha
' matanyula'), akhaulitseni
(Powavutitsa). Tsono ngati atalapa
Ndikukonza bwino (mkhalidwe
wawowo) Asiyeni. Ndithudi,
Mulungu Ngolandira kulapa,
Ndiponso Ngwachisoni chambiri.
17. Ndithudi kulapa
kovomerezeka ndi Mulungu
ndikwa omwe amachita zoipa
mwaumbuli kenako nkulapa
mwachangu. Amenewo ndiomwe
Mulungu Amawalandira kulapa
kwawo. Ndipo Mulungu Ngodziwa
Kwambiri Ngwanzeru zakuya. 2
^4 (I# 3jys3i QaK> '($&
1 (Ndime 15-6) Izi ndi ndime zimene zikufotokoza zazilango zolanga nazo awa>
a) Akazi amene amachitana ukwati okhaokha
b) Amuna amene amachitana ukwati okhaokha
c) Akazi ndi amuna amene akuchitana ukwati pamalo achabe apathupi. Zinthu
zonsezi nzoipa kwabasi, makamaka kuchitana ukwati amuna okhaokha ndi
kuchitananso ukwati akazi okhaokha.
2 Ndime iyi ikusonyeza kuti Mulungu amalandira kulapa kuchokera kwa aliyense
amene walapa. Komatu kuti kulapako kuvomerezeke, pafunika zinthu ziwiri:-
Surat4. An-Nisa'
Juzu 4
171
f *>»
t j-L— Jl 5jj-*»
18. Kulapa sikungalandiridwe
pa omwe Akuchita zoipa mpaka
imfa kumfikira M'modzi waiwo
(Pamenepo) nkunena: "Ndithudi
ine ndikulapa tsopano."
Ngakhalenso pa omwe akufa ali
Osakhulupirira. Iwo tawakonzera
Chilango chopweteka.
19. E inu amene
mwakhulupirira!
Sikovomerezedwa kwainu
kuwalowa Chokolo akazi
mowakakamiza. Ndipo
musawaletse (kukwatiwa Ndi
amuna ena) ndi cholinga choti
Muwalande zina mwa zomwe
Mudawapatsa, (nkosaloledwa
kutero) Kupatula ngati atachita
choipa Choonekera. Ndipo khalani
nawo Mwaubwino. Ngati
mutawada (Musalekane nawo),
mwina Mungade Chinthu chomwe
Mulungu waika Zabwino zambiri
mkati mwake. 1
a) Akachita utchimo alape mwachangu. Osati azingopitiriza kulakwako mpaka
akadzaona kuti ali pafupi kufa ndiye nkuyamba kulapa, zoterezi iyayi.
b) Utchimowo ukhale kuti adauchita chifukwa chaumbuli. Apa tikutanthauza
kuti panthawiyo iye adadzazidwa ndi zilakolako zauchimo ndipo zidamchititsa
kuti achimwe. Koma osati tchimolo likhale lolichita tsiku ndi tsiku popanda
kulabadira chilichonse. Kulapa kwa uchimo wotero Mulungu sangakulandire.
Ndipo mmalo mwake akamulanga ndi chilango chaukali.
1 Chisilamu chisanadze, chikhalidwe cha Arabu chidali chonchi:- Tate
wamunthu akamwalira ana ake amamlowera chokolo akazi ake omwe
sadabereke anawo. Mwana aliyense amalowa chokolo mwa mkazi watate
wake yemwe sadali mayi wake wom'bala.
a) Akafuna kumkwatira adali kumtenga.
b) Ndipo akafuna kumkwatitsa kwa mwamuna wina, amamlamula ndalama
mwamunayo iye natenga ndalamazo.
Surat4. An-Nisa' Juzu 4
172 t *j*-i
t s-LmJI 5jj-*>
20. Ndipo ngati mufuna
kusintha mkazi wina M'malo mwa
wina (pokwatira wina kusiya
Wakale) pomwe mmodzi waiwo
(woyambayo) Mudampatsa
milumilu yachuma, musatenge
(Kulanda) chilichonse. Kodi
mungachitenge Mwa chinyengo
ndi utchimo Woonekera?
21. Kodi mungachitenge bwanji
Pomwe mudalowana Wina ndi
mnzake, ndipo (Akazi) adalandira
kwa Inu chipangano cholimba?
22. Ndipo musakwatire akazi
amene adakwatiwapo Ndi atate
anu, kupatula zomwe zidapita,
(Musabwerezenso kuzichita).
Ndithudi, Chinthu ichi nchauve
ndipo nchodedwa Ndiponso
ndinjirayoipa. 1
c) Kapena amangomuvutitsavutitsa kuti akafuna adziombole yekha pomlipira
ndalama mwanayo.
d) Kapena amangommanga kuti asakwatiwenso mpaka imfa yake. Choncho
apa Mulungu akuletsa machitidwe oipawa,
1 Ndime iyi ndi zinzake zotsatira zikufotokoza zaakazi omwe ngoletsedwa
kuwakwatira pa Shariya ya Chisilamu. Ena mwa akaziwo ndi awa:-
1) Munthu sangakwatire mkazi yemwe bambo wake adamkwatirapo kapena
yemwe adakwatiwapo ndi gogo wake wakuchimuna kapena kuchikazi. Koma
osati amene adasiidwa ndimalume ake kapena m'bale watate wake.
Amenewa akhoza kuwakwatira.
2) Mayi wako yemwe adakubereka ndi mayi wamayi wako.
3) Mwana wako wodziberekera wekha, kapena mwana amene mwana wako
adabereka.
4) Tate wako wamkazi (zakhali) ndi alongo agogo ako.
5) Mayi wako wamng'ono (mbale wamayi wako) ndi mbale wamkazi wa agogo
ako akuchikazi.
6) Mwana wambale wako wobadwa naye bambo ndi mayi mmodzi kapena
wobadwa naye mayi mmodzi kapena bambo mmodzi ndi ana onse akazi
oberekedwa ndi mwanayo.
Surat4. An-Nisa' Juzu 5
173
*jjfc-l
t $,L**Jl ^JJ --
23. Kwaletsedwa kwainu
kukwatira Amayi anu, ana anu,
alongo anu, Azakhali anu, amayi
anu aang'ono Kapena aakulu, ana
achikazi am' bale Wanu, ana
achikazi a mlongo wanu, Amayi
anu amene adakuyamwitsani,
Alongo anu oberekedwa ndi amene
adakuyamwitsanipo. Mayi a akazi
anu, Ana achikazi owapeza amene
Mukuwasunga woberekedwa ndi
Akazi anu omwe mwalowana
nawo. Koma ngati simudalowane
nawo, Nkosaletsedwa kwa inu
kukwatira Amayi awowo; ndi
akazi a ana Amuna omwe
ngochokera kumisana yanu.
Ndiponso nkoletsedwa kwa inu
kukwatira Mophatikiza mkazi ndi
mchemwali wake obadwa naye
Kupatula zomwe zidapita.
Ndithudi Mulungu Ngokhululuka
kwambiri Ngwachisoni zedi.
24. Ndiponso (nkoletsedwa kwa
inu kukwatira) Akazi okwatiwa
kupatula chimene manja anu
akumanja apeza (mdzakazi). Hi ndi
lamulo la Mulungu lomwe lili
painu. Ndipo kwalolezedwa
kwainu (kukwatira Akazi) omwe
7) Mwana wamkazi wamlongo wako (mfumukazi) wamayi ndi bambo mmodzi
kapena wakumbali yabambo yokha kapenanso wakumbali yamayi yokha.
8) Mkazi yemwe adakuyamwitsapo ndi mayi ake amkaziyo kapena omwe
adamuyamwitsaponso iye.
9) Mkazi yemwe unayamwa naye bere limodzi.
10) Mayi wamkazi wanu.
Surat 4. An-Nisa' Juzu 5
174 • *>'
i iI~jS\ Ojj— »
sali m'gulu ili. Afunefuneni Ndi
chuma chanu m'njira yaukwati,
Osati chi were were. Choncho,
amene Mwawakwatira mwa iwo
nkusangalala nawo, apatseni
chiwongo chawo Chomwe
chakakamizidwa. Palibe kuipa
Kwa inu (kupereka) chomwe
mwagwirizana M'malo
mwachomwe chidatchulidwa.
Ndithudi, Mulungu Ngodziwa,
Ngwanzeru zakuya (Pokhazikitsa
Malamulo Ake).
25. Ndipo amene sangathe mwa
inu Kupeza chuma chokwatirira
mkazi Amene ali mfulu wa
Chisilamu, (akwatireni) Adzakazi
achisungwana a Chisilamu, Mwa
omwe manja anu akumanja apeza,
Mulungu akudziwa kwambiri
chikhulupiriro Chanu. Ndinu
amodzi kuchokera kwa wina ndi
mnzake (nonsenu ndinu ana a
Adam). Akwatireni ndi chilolezo
cha mabwana awo, Ndipo apatseni
chiwongo chawo Mwachilamulo.
(Akwatireni) omwe ali Akazi
odzisunga, osati achiwerewere
kapena ochita zibwenzi. Ndipo
akakwatiwa, kenako nkuchita
Chauve, chilango chawo nditheka
lachilango cha mfulu. kumeneko
(Kukwatira akapoloko) ndilamulo
kwa yemwe mwa inu akuopa kuti
angachite chi were were. Koma
Surat 4. An-Nisa' Juzu 5
175
t,j)r\
£ s-L-jJl &jj-»»
Ngati mutapirira (posiya kukwatira
Akapolo) ndibwino kwa inu
kutero. Ndipo Mulungu
Ngokhululuka, Ngwachisoni
chambiri.
26. Mulungu akufuna
kukufotokozerani Ndi
kukutsogolerani kunjiraZaomwe
adalipo patsogolo Panu; ndiponso
akufuna Kukufewetserani. Ndipo
Mulungu Ngodziwa kwambiri,
Ngwanzeru zakuya.
27. Ndiponso Mulungu
Akufuna kukufewetserani. Koma
amene akutsata zilakolako zawo
akufuna Mupotoke; kupotoka
kwakukulu.
28. Mulungu akufuna
kukupeputsirani, pakuti Munthu
adalengedwa wofooka. (Alibe
Mphamvu zathupi ngakhale
zolimbana ndi Zilakolako
zamoyo).
29. E inu amene
mwakhulupirira! Musadye chuma
chanu mwachinyengo Koma
m'njira yamalonda Ndi moyanjana
pakati panu. Ndipo Musadziphe
nokha (ngakhale Kupha anzanu).
Ndithudi, Mulungu ali Wachisoni
pa inu. l
®,
m,^m?* s
*&»%$
1 Apa akuletsa kudyerana chuma m'njira yachinyengo. Koma kugulitsana
malonda mwachimvano onse awiri nkomwe kukuloledwa. Ndipo Mulungu
pomwe wanena kuti musadziphe, m'mawu amenewa mukutanthauza munthu
Surat4. An-Nisa'
Juzu 5
176
o *jJH
i $.L«Jl &jj**>
30. Ndipo amene achite izi
molumpha Malire ndi mopanda
chilungamo, Iyeyo tidzamulowetsa
kumoto. Ndipo zimenezo
nzopepuka kwa Mulungu.
31. Ngati mudzitalikitsa
kumachimo Akuluakulu omwe
mukuletsedwa, Ndiye kuti
tikufafanizirani Zolakwa zanu
(zing'onozing'ono) Ndipo
tidzakulowetsani Malo aulemu. 1
32. Ndipo musazilakelake
(mwadumbo) Zomwe Mulungu
wawadalitsa nazo Ena mwainu.
j&3&
<3>
*i4$i&-Si*&3ji>
kudzipha yekha, ndi kupha Msilamu mnzake poti Msilamu ndi Msilamu
mnzake ali ngati thupi limodzi. Ndipo ngakhale yemwe sali Msilamu saloledwa
kumupha.
Mawu oti "kupha" akutanthauza kupha munthu nkuferatu nthawi yomweyo.
Mawuwa akutanthauzanso kuchita chinthu chomwe chingamchititse munthu
uja kuonongeka mwapang'onopang'ono mpaka mathero ake nkuferatu. Izi zili
monga amene akumwa mowa wakachasu kapena wina uliwonse, akudzipha
yekha. Kapenanso kuchita chinthu china chilichonse chomwe mathero ake
chimamupha munthu. Ndipo nayenso amene akuthandizira zimenezi, ali
m'gulu lakupha munthu.
1 Apa akuti ngati tipewa machimo akuluakulu, Mulungu adzatikhululukira
timachimo ting'onoting'ono.
Munthu nkovuta kuupewa utchimo ung'onoung'ono. Utchimotu suli wofanana.
Pali wina waukulu. Palinso wina wokulitsitsa. Ndipo pali waung'ono ndi wina
wochepetsetsa.
Machimo akuluakulu ali ngati awa: (a) Kuphatikiza Mulungu ndi mafano (b)
Kupha munthu wosalakwa. (c) Kuba. (d) Kuchita malonda akatapira (riba) (e)
Kumwa zoledzeretsa. ( f) Kuchita ziwerewere ndi zina zotero.
Tsono utchimo waung'ono uli monga: Kunena mawu osafunika ndi
kuchiyang'ana chinthu choletsedwa ndi zina zotero zomwe nzovuta munthu
kuzipewa. Choncho, munthu akapewa machimo akuluakulu ndiye kuti
adzamkhululukira machimo ang'onoang'ono ngati sakuwachita mochuiukitsa.
Enanso mwamachimo akuluakulu ndikusiya kutsata malamulo a Mulungu,
monga
(a) Kusiya kupemphera Swala zisanu (b) Kusiya kupereka Zakati ndi
zithandizo zina zofunika, (c) Kusiya kumanga m'mwezi wa Ramadhani, (d)
Kusiya kuchita Haji, (e) Kusiya kuyang'anira makolo ndi zina zotero.
Surat4. An-Nisa' Juzu 5
177
o *>i
t *L*Jt *jj-*»
Amuna ali ndi gawo (Lokwanira)
la zomwe apeza. Nawonso Akazi
ali ndi gawo(lokwanira) la Zomwe
apeza. Ndipo mpempheni Mulungu
zabwino zake. Ndithudi, Mulungu
Ngodziwa chilichonse. 1
33. Ndipo anthu tawaikira
alowa Mmalo pazomwe asiya
makolo Awiri ndi achibale. Ndipo
amene Mudagwirizana nawo
Chipangano, apatseni gawo lawo.
Ndithudi, Mulungu ndimboni Pa
chilichonse. 2
34. Amuna ndi ayang'aniri pa
akazi Chifukwa choti Mulungu
watukula Ena paulemerero
pamwamba Pa ena chifukwa cha
chuma chawo chimene apereka.
Choncho, akazi Abwino ndi omwe
ali omvera, Odzisunga ngakhale
amuna Awo palibe pakuti
Mulungu wawalamula
Kudzisunga. Ndipo akazi omwe
mukuopa Mnyozo wawo,
achenjezeni; ndipo Kenako
1 Apa akuletsa anthu kuchitirana dumbo. Koma chofunika nkuti munthu
alimbike kugwira ntchito kuti nayenso apeze chomwe mnzake wapeza. Osati
kumchitira dumbo ndi kumuda, pakuti iye palibe chimene wakulanda.
Adagwira ntchito molimbika ndipo Mulungu wampatsa. Iwenso limbikira
kugwira ntchito Mulungu akupatsa. Wopemphedwa ndi kupatsa ndiyemweyo
Mulungu wathu.
2 Kale Chisilamu chisadadze, munthu ankati akatenga mwana wamunthu wina
nkumulera ankamuyesa mwana wake weniweni pomulowera chokolo
pachilichonse ngati mwanayo atafa. Ngakhale makolo ake enieni ndi abale
ake atakhalapo sadali kuwagawira chilichonse. Tsono Chisilamu chidathetsa
mchitidwe umenewu ponena kuti munthu aliyense azimlowa chokolo ndi abale
ake.
Surat4. An-Nisa' Juzu 5
178
*jjfc-l
i tL— ul ^jj-* 1
achokereni pamphasa. (Apo ayi),
akwapuleni; (kukwapula
Kosavulaza) koma ngati
Akukumverani, musawafunire
njira yowavutitsira. Ndithu
Mulungu ndi Yemwe ali
wapamwamba, Wamkulu (kuposa
inunonse). 1
35. Ndipo (inu aweruzi) ngati
muopa mkangano pakati pawo
(pamwamuna Ndi mkazi wake),
tumizani nkhoswe yakuchimuna
ndi nkhoswe yakuchikazi. Ngati
iwo atafuna kuyanjanitsa, Mulungu
awapatsa mphamvu zoyanjanitsira
Pakati pawo (okanganawo).
Mulungu Ngodziwa nkhani
zobisika, ndiponso Ngodziwa
nkhani zoonekera.
1 Apa akuti amuna ndi amene akhale ndi ulamuliro paakazi awo,
powatsogolera kumiyambo yabwino. Osati kuti mkazi adzitukumule
kwamwamuna wake poti iye ngophunzira zedi kapena wanzeru zochuluka
kotero kuti mwamuna m'nyumba osamuyesa kanthu. Ngati atero ndiye kuti
sakhala Asilamu owona.
M'ndimemu atchulamonso makhalidwe ofunika kuti akazi akhale nawo. Ndipo
atchulamo malangizo olangira nawo mkazi ngati samvera. Choyamba
amchenjeze ndi mawu. Ngati kuchenjezako sikunathandize, asagone naye
limodzi pamphasa. Ndipo ngati akupitirizabe kuchita mnyozo akupatsidwa
chilolezo mwamuna kuti amlange pommenya mwakumuopyeza, osati
kumenya komgulula nako mano. Komabe mahadisi amtumiki (madalitso ndi
mtendere zikhale naye) akunena kuti asanaganize zommenya Ayeseyese
kumkonza ponena naye mofewa ndi kumuonetsa kulakwa kwake. Ngati
atalephera zonsezi, aitane anthu kuti adzawayanjanitse m'njira yabwino.
Naonso anthuwo akhale ndi cholinga choyanjanitsa osati kupasula.
Amunanso akuwachenjeza apa kuti iwo ndi amene ali ndi nyonga ndi udindo.
Mulungu ndiye Wamkulu kuposa iwo amunawo. Mawu oti "Hafizatu Lilighaibi"
maulama ena akulitanthauzira kuti "Akhale osunga chinsinsi," chimene chili
pakati pa iwo ndi amuna awo ndi zonse zomwe zimachitika m'nyumba, pakuti
nthawi zambiri akazi sakhalira kuulula zam'nyumba.
Surat 4. An-Nisa' Juzu 5
179
*j*-l
t tL^Jl ^JJ— '
36. Ndipo mpembedzeni
Mulungu, ndipo Musamphatikize
ndi chilichonse; ndipo Achitireni
zabwino makolo awiri, ndi
Achibale, ndi ana amasiye ndi
masikini Ndi mnansi woyandikana
naye Nyumba, ndi wapadera
wogundizana Naye nyumba, ndi
mnzako wokhala Naye limodzi,
ndi wapaulendo yemwe Alibe
choyendera, ndi omwe manja anu
akumanja apeza (adzakazi).
Ndithudi, Mulungu sakonda
wodzitukumula Ndi wodzitama. 1
37. Omwe amachita umbombo
ndi Kulamula anthu kuchita
Umbombo ndi kubisa zabwino
Zomwe Mulungu wawapatsa.
Komatu osakhulupirira
Tawakonzera chilango
choyalutsa. 2
38. Ndi omwe akupereka chuma
Chawo modzionetsera kwa Anthu
ndipo sakhulupirira Mulungu ndi
tsiku lomaliza. Ndiponso yemwe
M'ndime iyi akuwalamula anthu kuti apembedze Mulungu yekha ndi
kumpempha lye yekha. Asapembedzenso china chilichonse, chamoyo
kapena chakufa. Ndikuti awachitire zabwino makolo ake ndi onse amene
awatchula m'ndimeyi. Sibwino kuthandiza anthu akumbali pomwe anthu
omwe uli nawo pafupi sunawathandizepo.
2 Kubisa zonse zomwe Mulungu wawapatsa kuli monga munthu kukhala ndi
maphunziro koma osaphunzitsa anthu kotero kuti nkufa nawo popanda
kuphunzitsapo aliyense. Kutero sibwino. Koma akafuna kukalowa m'munda
wa Mtendere wa Mulungu nkofunika kuti achite zinthu zabwino ncholinga
chokondweretsa Mulungu. Osati kuti anthu amuone ndi kumtama. Amene
akuchita chinthu chabwino ncholinga choti anthu amtamande, sakalandira
mphoto iliyonse pa tsiku lomaliza.
Surat4. An-Nisa' Juzu 5
180
o *£\
t tL-jJl ^JJ— '
satana Angakhale bwenzi lake,
ndithudi Ali ndi Bwenzi loipa.
39. Kodi pakadakhala vuto lanji
kwa Iwo ngati akadakhulupirira
Mulungu ndi tsiku lomaliza
Napereka zina mwa zomwe
Mulungu wawapatsa? Ndipo
Mulungu ali Wodziwa bwino za
iwo.
40. Ndithudi, Mulungu sachitira
(anthu) zosalungama Ngakhale
chinthu cholemera ngati Nyerere
yaing'ono; ngati chinthucho chili
Chabwino amachichulukitsa ndi
kupereka Malipiro akulu
kuchokera kwa lye.
41. Nanga zidzakhala bwanji
tikadzabweretsa Mboni pa
mbadwo uliwonse
ndikukubweretsa Iwe (Mneneri
Muhammad {SAW}) kuti ukhale
Mboni pa mbadwo uwu.
42. Tsiku limenelo aja omwe
sadakhulupirire Namunyoza
Mtumiki, adzakhumba kuti Nthaka
ikadafafanizidwa paiwo
(Akwiriridwe, asaukitsidwe).
Ndipo sadzatha kum'bisa Mulungu
Nkhani iliyonse (m' zomwe
Adachita m'moyo wapadziko).
43. E inu amene
mwakhulupirira! Musayandikire
Swala uku muli oledzera, Mpaka
mudziwe chimene mukunena;
d&fc
Surat4. An-Nisa'
Juzu 5
181
tjir)
t «.l~*Jt *JJ~*
Ngakhalenso pamene muli Ndi
janaba (musapemphere Kufikira
mutasamba) kupatula Amene ali
paulendo(achite tayammam) Ngati
muli odwala, kapena muli
paulendo, Kapena m'modzi wanu
wadza kuchokera Kuchimbudzi,
kapena mwakhudza Akazi (m'njira
yaukwati) ndipo Simunapeze
madzi (osamba) chitani
Tayammamu ndi dothi labwino;
Lipakeni kunkhope kwanu ndi
M'mikono mwanu. Ndithudi,
Mulungu ngofafaniza machimo
Anu, ndiwokhululuka.
44. Kodi sukuwaona omwe
adapatsidwa Gawo la (nzeru
zozindikira) Buku (la Mulungu,
omwe ndi Ayuda ndi Akhrisitu).
Akuzisankhira kusokera ndiponso
akufuna mutasokera (Kusiya njira
yabwino) 1
1 (Ndime 44-6) Apa akutchula kuipa kwina kwa Ayuda ndi Akhrisitu. Ayuda ndi
Akhirisitu adali kusintha mawu omwe adalimo m'mabuku a Taurati ndi Injili,
makamaka mawu amene adali kusonyeza za uneneri wa Muhammad
(madalitso ndi mtendere zikhale naye). Kapena adali kuwatanthauzira m'njira
zina zolingana ndi zolinga zawo. Pamene adali kudza kwa Mtumiki
Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale naye) makamaka Ayuda,
akawalalikira mawu achipembedzo, ankati; "Tamva, titsatira," pomwe
m'mitima mwawo akuti "Sititsatira zonse zomwe ukunena. Koma
tikungokunyenga chabe." Amati akadza nkumva momwe maswahaba adali
kunenara ndi Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye), Mtumiki
akawalalikira, amati "Ismaa ghayra musmaa" monga mwa chizolowezi cha
Arabu akauzidwa mawu ofunika. Tanthuzo lake nkuti, "Imva siumvanso
choipa kuchokera kwa ife ngati Mulungu afuna." Naonso Ayuda adali
kumnenera Mtumiki mawu omwewa. Koma m'mitima mwawo akulinga
tanthauzo lina. M'mitima mwawo amalinga kuti, "Siumva zabwino kuchokera
kwa ife ngati Mulungu afuna. Koma zokusowetsa mtendere zokhazokha."
Ndipo amati akabweranso Ayudawo nkumva maswahaba akumuuza Mtumiki
Surat 4. An-Nisa' Juzu 5
182
o *jJH
i $.L*Jl tjf*
45. Ndipo Mulungu akudziwa
Bwinobwino za adani Anu. Ndipo
Mulungu Akukwanira kukhala
Mtetezi. Mulungu akukwananso
kukhala mthandizi.
46. Mwa Ayuda alipo omwe
amasintha mawu kuwachotsa
m'malo mwake. Ndipo amanena
(Chabe ndi milomo yawo);
"Tamva;" (pom we Mitimayawo
ikunena) : "Tanyoza". (ndipo
Akunena kuuza Mtumiki): "Imvera
koma wosamveredwa (ndipo
pakati pakuyankhula Kwawo
amanena mawu akuti) 'Raaina'
(Ncholinga chomnenera kuti iye
ndimbutuma). Ndipo mokhotetsa
zoyankhula zawo (kuti Akhale
ngati akumunenera zabwino
pomwe Akumtemberera) ndi
cholinga chotukwana
Chipembedzo (cha Chisilamu).
Akadakhala kuti Iwo adanena;
"Tamva ndipo tarn vera; ndipo
Imva, utiyang'anire" (mmalo
monena kwawo Kwakuti
'Raaina'), zikadakhala zabwino
ndizolingana kwa iwo. Koma
Mulungu adawatemberera
kuti; "Raaina". Kutanthauza kuti, "Tiyang'ane anthu ako ndidiso lachifundo,"
iwonso amayankhula mawu omwewa, koma mokhotetsa pang'ono mpaka
kusinthika tanthauzo lake. M'chiyankhulo cha chiyuda limatanthauza kuti "E
iwe mbutuma!" Ndipo iwo m'kunena kwawo amalinga tanthauzo limeneli.
Choncho Asilamu anawauza kuti azigwiritsira ntchito mawu oti "Unzuruna."
Ndipo mawuwa tanthauzo lake ndilofanana. Koma mawu awa sakadatha
kuwakhotetsa.
Surat 4. An-Nisa' Juzu 5
183
o ljk\
t «.L«Jl djj~*>
chifukwa cha kusakhulupirira
kwawo. Sakhulupirira koma
pang'ono basi.
47. E inu amene mwapatsidwa
Buku! Zikhulupirireni zomwe
tavumbulutsa Zikutsimikizira
zomwe muli nazo Tisanazisinthe
nkhope zanu ndi Kuzitembenuzira
kumbuyo kwake, Kapena
tisanawatemberere monga momwe
tidawatemberera omwe
Sadalemekeze kupatulika kwa
tsiku la Sabata. Ndipo lamulo la
Mulungu ndilochitikadi.
48. Ndithudi Mulungu
sangakukhululuke Kuphatikizidwa,
koma amakhululuka (Machimo
ena) osati amenewa kwa Amene
wamfuna. Ndipo amene
Angamphatikize Mulungu,
Ndithudi, wadzipekera uchimo
waukulu.
49. Kodi sukuwaona omwe
akudziyeretsa okha? Koma
Mulungu amamyeretsa amene
wamfuna Pomulimbikitsa kuchita
zabwino. Ndipo
sadzaponderezedwa angakhale
Ndikachinthu kochepa konga
kaulusi kokhala mkati mwakhokho
latende. 1
9.1" . '\'ll "['•*'&')> it\
1 Ayuda adali kunyada chifukwa choti iwo adali nawo Aneneri, ndiponso
makolo awo omwe adali olungama. Ankati: "Poti makolo athu adali olungama
Surat4. An-Nisa' Juzu 5
184 • *>•
t f-L^Jl *JJ**
50. Taona, momwe akumpekera
Mulungu bodza! Ndipo izi
zikukwana kukhala tchimo
loonekera!
51. Kodi sukuwaona omwe
apatsidwa Gawo la nzeru
zozindikira Buku (La Mulungu)?
Amakhulupirira Mafano ndi
asatana, ndipo akumati kwa amene
sadakhulupirire "Awa ali panjira
yoongoka kwabasi kuposa
okhulupirira (Asilamu)" 1
52. Iwo ndi omwe Mulungu
Wawatemberera. Ndipo amene
palibe chochititsa mantha paife. Utchimo uliwonse umene ife tingachite
Mulungu adzatikhululukira ngakhale utchimowo utakhala waukulu chotani."
Iwo ankadzitchanso kuti adali okondedwa a Mulungu. Ndipo iwowo ngomwe
akuwatchula m'ndime iyi kuti "Kodi saona amene akudziyeretsa okha ndi
mawu okha ochokera m'milomo popanda kuchita zimene adawalamula ndi
kusiya zomwe adawaletsa?"
Mwa Asilamu aliponso ena omwe ali ndi maganizo onga amenewa.
Amangonyadira zochita zamakolo awo popanda kutsanzira chikhalidwe
chamakolo awowo.
1 Mawu oti "Jibti ndi Twaghut" amanena za chinthu chomwe anthu
akuchipembedza chamoyo kapena chakufa chomwe sichili Mulungu weniweni
monga momwe lilili dzina loti Shetani. Iloli limatchulidwa kwa aliyense amene
akusokeretsa anthu ku njira ya Mulungu. Chifukwa cha kuipidwa ndi Asilamu,
Ayuda adapita ku Makka kukapalana ubwenzi ndi Akuraishi ndi Arabu ena
opembedza mafano kuti athandizane nawo kumthira nkhondo Mtumiki
Muhammad(SAW) pamodzi ndi omtsatira ake kuti achithetseretu chipembedzo
cha Chisilamu. Choncho akuluakulu a Chiyuda atafika ku Makka adagwadira
mafano ncholinga chofuna kukondweretsa Akuraishi pomwe Ayudawo adali
eni mabuku omwe salola kupembedza mafano. Adawalimbikitsanso Akuraishi
aja powauza kuti: "Zochita zanu pachipembedzo chanu nzabwino kuposa
zochita za Muhammad pachipembedzo chake chimene wadza nacho." Iwo
amanena izi akudziwa kuti akunama. Cholinga chawo kudali kupeza
chithandizo kwa iwo kuti athetse Chisilamu chifukwa chakudzazidwa ndi njiru
m'mitima mwawo ponena kuti: "Nchotani kuti Muhammad (SAW) alandire
chisomo chauneneri?" Iwo ankachita izi ngati kuti ufumu wa Mulungu udali
m'manja mwawo kuti iwo ndi amene amagawa zachifundo cha Mulungu,
chonsecho, Mulungu amapereka kwa yemwe wamfuna. lye amachita chimene
wafuna. Safunsidwa ndi aliyense pachimene wachita. Koma iwo amafunsidwa.
Surat4. An-Nisa' Juzu 5
185
frjJrl
i *L*Jt 3jj-«*
Mulungu wamtemberera,
Simungathe kumpezera
wompulumutsa.
53. Kodi ali ndi gawo la ufumu
(Wa Mulungu? Nchifukwa Ninji
akunyasidwa munthu wina
akaninkhidwa utumiki)?
Zikadatero ndiye kuti
sakadawapatsa anthu ngakhale
kochepa kwambiri monga Khokho
latende. 1
54. Kodi akuchitira anthu
dumbo Pazomwe Mulungu
wawapatsa ndiufulu wake?
Choncho tidalipatsa banja la
Ibrahim Buku ndi nzeru. Ndipo
tidawapatsa ufumu waukulu.
55. Choncho alipo ena mwaiwo
amene anazikhulupirira izi,
ndiponso alipo ena mwaiwo omwe
adziika nazo kutali. Ndipo
Jahanama ikukwanira kukhala
moto waukali wowatentha.
56. Ndithu, amene
sadakhulupirire zizindikiro zathu,
tidzawalowetsa kumoto. Nthawi
±9*' K*' 94999 s s'\ 9*&99*<
1 (Ndime 53-4) Ndime izi zikusonyeza kuti zonse zimene Ayuda ankawachitira
Asilamu nchifukwa chadumbo basi. Ankawawidwa nawo mitima chifukwa
choti Asilamu apeza chisomo cha Mulungu. Palibe chinthu chimene
chimaletsa anthu kutsata choonadi kuposa dumbo. Ngati utamchitira dumbo
munthu sungalole kutsata langizo lake lililonse ngakhale litakhala lopindulitsa
pano padziko lapansi ndi tsiku lomaliza Dumbo ndi lomwe likuletsa anthu
ambiri kutsata choonadi. Choncho tiyeni tipewe khalidwe limeneli kuti titsatire
choonadi paliponse pamene chachokera. Ndikutinso tipeze mtendere
m'mitima mwathu. Dziwani kuti dumbo nlomwe lidamchititsa Iblis kukhala
wotembereredwa.
Siirat4. An-Nisa' Juzu 5
186 • *>»
t tL— Jl <*JJ-"
WU
esa®
iliyonse yomwe makungu awo
adzikapserera tidzidzawasinthira
makungu ena kuti adzapitirize
kulawa chilango. Ndithudi,
Mulungu Ngwamphamvu zoposa,
Ngwanzeru zakuya. 1
57. Ndipo amene akhulupirira
ndikuchita zabwino,
Tidzawalowetsa m'minda mom we
mitsinje ikuyenda pansi ndi
patsogolo pake. Adzakhala
mmenemo muyaya. Ndipo Iwo
adzapeza mmenemo akazi
oyeretsedwa (ku Uve wamtundu
uliwonse) ndi kuwalowetsa ku
Mithunzi yabwino kwambiri.
58. Ndithudi, Mulungu
akukulamulani Kubweza kwa eni
zomwe mwakhulupirika nazo.
Ndipo pamene mukuweruza
pakati paanthu, Weruzani
mwachilungamo. Ndithu,
malangizo amene Mulungu
akukulangizani, ngabwino
Kwambiri. Ndithudi, Mulungu
Ngwakumva, Ngoona. 2
1 (Ndime 56-7) Apa akutchula zamalipiro a anthu ochita zabwino ndi malipiro
a anthu ochita zoipa umu ndi momwe ulili ulaliki wa Qur'an. Qur'an
ikafotokoza za anthu ochita zoipa imatsatiza pompo kufotokoza zotsatira za
anthu ochita zabwino. Pamenepa akunena kuti aliyense adzalandira
malipiro a zochita zake, abwino kapena oipa. Sakawomboledwa chifukwa
chaubwino wa munthu wina. Zochita zake ndizo zikamuombola kapena
kukamponya kuchionongeko.
2 Pali anthu ena amene amati anzawo akawasungitsa zinthu kuti akhulupirike
pazimenezo, mwini zinthu uja akafa kapena kuti panalibe umboni wokwanira,
amazitenga zinthuzo poganizira kuti palibe chomwe chingawavute popeza
mwini zinthuzo adamwalira ndipo umboni wokwanira palibe. Chikhalidwe
chotere si cha Chisilamu, Chisilamu sichifuna machitidwe otere.
Surat 4. An-Nisa' Juzu 5
187
3 frjA-l
i s.l*Ji ^j-*
59. E inu amene
mwakhulupirira! Mumvereni
Mulungu ndiponso Mumvereni
Mtumiki, ndi omwe ali ndi udindo
painu. Ngati Mutatsutsana
pachinthu chilichonse, Chibwezeni
kwa Mulungu ndi Mtumiki Wake,
Ngatidi mukukhulupirira Mulungu
ndi tsiku lomaliza, kutero
ndibwino; Ndipo zotere zili ndi
zotsatira zabwino. 1
60. Kodi sukuwaona omwe
akungonena chabe kuti
akhulupirira zomwe
zavumbulutsidwa kwa iwe ndi
zomwe zidavumbulutsidwa
patsogolo pako, Pomwe iwo
akufuna kuti akaweruzidwe ndi
maweruzo osagwirizana ndi
Shariya, Pomwenso alamulidwa
kukana njira Zotere? Koma satana
akufuna Kuwasokeretsa, kusokera
kwakutali.
61. Ndipo akauzidwa: "Idzani
Kuzomwe Mulungu
wavumbulutsa, Ndipo (idzani) kwa
Mtumiki." Uwaona achinyengo
akudziika kutali kwabasi ndi iwe.
oji^s %;, Iv* tattoo ujj
£\*9 f 9 *ii* ' * 9*9'
1 Aliyense amene amdzoza utsogoleri nkofunika kuti anthu amumvere ngati
iye akulamula zabwino. Pagulu la anthu ngati sipakhala mtsogoleri
womumvera, ndiye kuti pamapezeka zisokonezo ndi ziwawa kotero kuti zinthu
zawo siziyenda bwino. Chisilamu sichiloleza machitidwe achipolowe ndi
ziwawa. Chisilamu chimakonda bata ndi mtendere ndi kuti pasapezeke anthu
ena owachenjerera anzawo. Komatu atsogoleriwo awamvere akalamula mwa
chilungamo popanda kulakwira Mulungu. Koma ngati akulakwira Mulungu
asawamvere. Pamenepo atsate chomwe Mulungu wawalamula ndi Mtumiki
Wake.
Siirat 4. An-Nisa' Juzu 5
188
o fjA-i
t «.L*Jt 3jj~*
62. Kodi zingakhale bwanji
litawabwerera vuto chifukwa cha
zomwe manja awo adatsogoza?
Kenako nkukudzera (iwe Mtumiki)
uku akulumbira: "Tikulumbira
Mulungu; Sitinafune china
chilichonse koma zabwino zokha
ndi chimvano."
63. Iwo ndi omwe Mulungu
akudziwa zomwe zili mmitima
mwawo. Choncho dzipatule kwa
iwo, Ndipo alangize ndi kuwauza
Mawu ogwira mtima.
64. Ndipo sitidamtumize
Mtumiki aliyense koma Kuti
azimveredwa mwa lamulo la
Mulungu. Ngati akadakudzera
pamene adadzichitira okha Zoipa,
(chifukwa chokafuna chiweruzo
cha Satana) napempha
chikhululuko kwa Mulungu (Naye)
Mtumiki nkuwapemphera,
ndithudi, Akadampeza Mulungu
ali wolandira kulapa kwawo ali
Wachisoni.
65. Ndikulumbira (m'choonadi
cha) Mbuye wako, Iwo
sangakhale okhulupirira moona
Pokhapokha akuyese muweruzi
wawo Pazomwe akukangana
pakati pawo. Kenako Asaone vuto
mmitima yawo pazomwe
waweruza, Ndipo adzipereke
Surat4. An-Nisa'
Juzu 5
189 • *>»
t tL-jl djjMtl
kwathunthu (pogonjera Chiweruzo
chako). 1
66. Ndipo ngati
tikadawakakamiza kuti: "Dzipheni
nokha," kapena: "Tulukani
m'nyumba Zanu; (Mupite
kunkhondo kapena musamuke),"
Sakadachita zimenezo kupatula
ochepa Mwa iwo. Koma
akadachita zomwe auzidwa,
zikadakhala zabwino kwa iwo.
Ndipo zikadawalimbikitsa
Kwambiri (Chisilamu chawo)
67. Ndipo zikadatero,
Tikadawapatsa malipiro Aakulu
ochokera kwa Ife.
68. Ndiponso tikadawatsogolera
Ku njira yoongoka. (Yokawafikitsa
ku Munda wamtendere).
69. Ndipo amene angamvere
Mulungu Ndi Mtumiki wake,
iwo wo Ndi omwe adzakhale
pamodzi ndi Omwe Mulungu
adawadalitsa, Kuyambira aneneri,
Olungama, maShahidi(asilamu
ofela kunkhondo) ndi anthu
®Q&J$&&&$$&
i&SRJv&i&Z
©
** 9
1 Ngati anthu atakangana pachinthu ena nati chimenechi nchofunika pomwe
ena akuti nchosafunika, onsewo abwere nkuyang'ana kuti mawu a Mulungu
ndi mawu a Mtumiki akunena chiyani pachinthu choterecho. Tsono akapeza
malangizo a Mulungu ndi Mtumiki pachimenecho awatsatire. Aliyense waiwo
asakhumudwe poona kuti zomwe amalimbikira sindizo zomwe Mtumiki
(madalitso ndi mtendere zikhale naye) adaphunzitsa. Koma agonjere
kwathunthu kuzophunzitsa za Mtumikizo. Chilichonse chimene Mtumiki
walangiza asawiringule nacho. Koma angotsatira basi.
Surat4. An-Nisa' Juzu 5
190 ° *>■'
t $-L— Jl 5jj-»»
abwino. Taonani ubwino wokhala
Nawo pamodzi iwowo! 1
70. Umenewo ndiubwino
wochokera Kwa Mulungu. Ndipo
Mulungu Ngodziwa mokwanira.
71. "E inu amene
mwakhulupirira! Khalani
ochenjera (ndi adani anu;
musanyengedwe Nawo). Pitani
(kunkhondo) gulu limodzilimodzi,
Kapena pitaniko nonsenu pamodzi
(monga Momwe Mtumiki
angakulangizireni) .
72. Ndipo alipo ena mwainu
otsalira M'mbuyo sapita
kunkhondo, (Ndiponso amaletsa
anzawo). Ngati Vuto litakupezani,
(yense waiwo) amanena:
"Mulungu wandichitira chisomo
Posakhala m'gulu lawo
kumeneko."
73. Koma ubwino wa Mulungu
ukakupezani (monga Kupeza
chuma chambiri chosiidwa ndi
adani, Kapena kupambana
kumene) amanena ngati kuti
Padalibe chikondi pakati panu ndi
pakati Pake, "Kalanga ine!
1 Aliyense wochita zabwino zomwe nzovomerezeka ndi malamulo a Chisilamu
akalowa Kumunda Wamtendere. Ndipo aliyense amene akalowe kumundako,
akakumana ndi anzake kumeneko. Ndipo nthawi zina azikakhala nawo
pamodzi ngakhale kuti malo awo okhalamo adzakhala osiyanasiyana
chifukwa chakulekana maulemerero awo amene adawapeza kupyolera
m'zochita zawo.
Surat4. An-Nisa' Juzu 5
191
o *jk-\
i *L«Jl *JJ- t '
Ndikadakhala nawo Pamodzi
pankhondo imeneyi, (ndiye kuti)
Ndikadapambana; kupambana
kwakukulu."
74. Choncho, amenyane panjira
ya Mulungu omwe akugulitsa
moyo (Wawo) wadziko lapansi ndi
Tsiku lomaliza. Ndipo amene
angamenyane panjira ya Mulungu,
Kenako ndikuphedwa kapena
Kupambana tidzampatsa malipiro
aakulu.
75. Mwatani inu osamenyana
panjira ya Mulungu,
(ndikuwapulumutsa) Omwe ali
ofooka, aamuna ndi Aakazi ndi
ana, omwe akunena: "Mbuye
wathu! Titulutseni m'mudzi Uwu
omwe anthu ake ndiopondereza;
Ndipo tipatseni mtetezi wochokera
Kwa Inu; ndiponso tipatseni
Mthandizi wochokera kwa Inu." 1
76. Amene akhulupirira,
akumenya (nkhondo) Panjira ya
Mulungu. Koma amene
Sadakhulupirire, akumenya
^Lii'da'-ft
si
®vj^'^y&&i\%
Pamene Mtumjki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) adasamuka ku
Makka kukakhala ku Madina, Asilamu ena aamuna ndi aakazi adatsalira ku
Makka chifukwa chakuti abale awo adawaletsa. Ndipo chifukwa chakufooka
kwawo sadathe kuthawa mozemba namangokhala konko ku Makka
akuwachitira zoipa zambiri ndi kumawanyoza. Choncho Asilamu adawauza
kuti ngati kuzakhale kololezedwa kuchita nawo nkhondo Akuraishi a m'Makka
adzamenyane nawo Akuraishiwo molimba kufikira adzawapulumutse. Asilamu
adakwaniritsa lonjezolo. Adamenya nkhondo mpaka kugonjetsa mzinda wa
Makka ndi kuwapulumutsa anzawo amene adali kupempha Mulungu kwa
nthawi yaitali kuti awapulumutse ku anthu oipa.
Surat 4. An-Nisa'
Juzu 5
192
o ^\
t *L**J1 ^JJ— '
(nkhondo) Panjira ya Satana.
Choncho menyanani Ndi abwenzi
a Satana. Ndithudi, Ndale za
Satana nzofooka.
77. Kodi sukuwaona omwe
Adauzidwa kuti: "Aletseni manja
anu (kumenyana ndi
osakhulupirira mpaka lidze lamulo
lakumenyana)? Koma tsono
pempherani Swala ndikupereka
chopereka basi. Koma pamene
adakakamizidwa Kumenyana,
pompo gulu Una la Iwo lidaopa
anthu (Osakhulupirira) Ngati
likuopa Mulungu kapena
kuposerapo. Ndipo adati: "Mbuye
Wathu! chifukwaninji
mwatikakamiza kumenyana? Ha!
Mukadatichedwetsa Kufikira *
nyengo yochepa, (Zikadakhala
Bwino)." Nena: "Chisangalalo
cham'dziko n'chochepa. Koma
tsiku Lomaliza ndilabwino
kwambiri kwa Amene akuopa
(Mulungu). Ndipo
Simudzaponderezedwa ngakhale
pachinthu Chaching'ono monga
ulusi Wakhokho la tende!"
78. Paliponse pamene
mungakhale Imfa ikupezani
ngakhale mutakhala M'malinga
olimba ngati ubwino Utawafika
(Amushirikina ndi Amunafikina)
amati: "Ubwinowu, Ukuchokera
kwa Mulungu." Koma choipa
©S^^yl^lu^f))
Surat4. An-Nisa'
Juzu 5
193
o *jA-i
£ 5-L-Jl 5jj-**
chikawafikira, Amati: "Ichi
chachitika chifukwa chaiwe
(Muhammad)." Nena: "Zonse
zachokera Kwa Mulungu." Kodi
ngotani anthu Awa, sangathe
kuzindikira nkhani? 1
79. Chabwino chimene
chakufikira (iwe munthu) Ndiye
kuti chachokera kwa Mulungu.
Koma Choipa chimene chakufikira
ndiye kuti Chachokera kwa iwe
mwini (chifukwa cha Zochita zako
zoipa). Ndipo takutumiza (iwe
Muhammad) kwa anthu kukhala
Mtumiki. Ndipo Mulungu
ndimboni yokwana.
80. Yemwe angamvere
Mtumiki ndiye kuti wamvera
Mulungu, (chifukwa chakuti zonse
zomwe iye Akulamula
nzotumidwa ndi Mulungu). Ndipo
Amene atembenukire kutali
(kunyoza iwe, Ndiye kuti zoipa zili
paiye mwini). Sitidakutumize
iweyo kukhala kapitawo pa iwo.
81. Amati: "Tikumvera." Koma
akachoka Kwaiwe, gulu lina la iwo
limapangana Usiku zosagwirizana
ndi zomwe Ukunena (pamaso
pawo). Koma Mulungu akulemba
zonse Zomwe akupangana.
Choncho Apatukire ndipo
1 Ndime iyi ikutsimikizira kuti imfa njosathawika. Paliponse pamene munthu ali
impeza.
Surat 4. An-Nisa' Juzu 5
194 • *j*-i
£ £L*Jl OjJ~*>
yadzamira kwa Mulungu. Ndipo
Mulungu Ndimtetezi wokwanira.
82. Kodi bwanji sakuiganizira
Qur'an? Ndipo ikadakhala kuti
siikuchokera Kwa Mulungu,
ndithudi, mmenemo Akadapeza
kusiyana kwambiri,
(Mukadapezeka mawu otsutsana;
Koma Qur'an siili choncho). 1
83. Ndipo chikawadzera
chinthu Chilichonse chachitetezo
kapena Mantha, amachifalitsa.
Ngati Akadachibweza kwa
Mtumiki Ndi kwa omwe all ndi
udindo Pa iwo, akadachidziwa
omwe Amafufuzafufuza zinthu
mwa Iwo (kuti kodi nzoyenera
Kuzifalitsa kapena ayi).
1 M'ndime iyi akuti Qur.an iyi mawu ake ngolingana. Siotsutsana ayi. Ndipo
palibe amene angabweretse mtsutso wakuti mawu ena omwe ali m'bukuli
ngabodza pachifukwa chakutichakuti. Palibe buku lomwe munthu adalemba
lomwe lidabweretsa mtsutso weniweni wakuti Qur'an simawu a Mulungu
pachifukwa chakutichakuti. Ndipo silidzapezeka buku lotero mpaka dziko
lapansi lidzatha. Koma mwina anthu akhoza kumayankhula chabe popanda
kubwera ndi mtsutso weniweni wokhala ndi umboni wooneka. Kuona kwa
Qur'an kwatsimikizika pazinthu izi:- Qur'an idafotokoza nkhani zakale zomwe
zidachitika Mtumiki Muhammad (SAW) asanabadwe pomwe iye sankadziwa
kulemba ndi kuwerenga mabuku. Quran idafotokozanso zamtsogolo. Ndipo
zina mwaizo zaonekera kale poyera: (1) Qur'an idati: "Chinthu chilichonse pali
chachimuna ndi chachikazi". Yang'anani ndime ya 36 ya Surat Yasin. (2)
Kuti dziko lapansili lidalumikizana ndi kumwamba monga ikufotokozera Surat
Anbiyaa ndime ya 30. (3) Kuti moyo umadalira madzi, monga momwe ndime
ya 30 ya m'Surat Anbiyaa ikulongosolera. (4) Kuti anthu amene ali kutali
kwambiri adzatha kumva zimene anthu ena akutali akunena. Monga momwe
ndime ya 44 ya m'Surat Aaraf. (5) Ndi kuti anthu adzakwera kumwamba
monga momwe ikulongosolera ndime ya 13 yam'Surat Jathiya. m'Qur'an
muli zambiri zimene adafotokoza kuti zidzachitika mtsogolo. Ndipo zambiri
mwa izo zachitikadi, anthu aziona. Ndipo zonsezi zikutsimikizira kuti Qur'an
ndi mawu a Mulungu.
Surat4. An-Nisa' Juzu 5
195
O *>!
i *L«Ji Sjj-*'
Pakadapanda ubwino wa Mulungu
ndi chifundo chake Pa inu,
ndithudi, mukadamtsatira Satana
kupatula ochepa.
84. Choncho menya nkhondo
panjira Ya Mulungu,
suukukakamizidwa (Za anthu ena)
koma iwe mwini, Ndipo
akhwirizire Asilamu. Ndithu
Mulungu angatsekereze mtopola
Wa omwe sadakhulupirire. Ndipo
Mulungu Ngwaukali Kwambiri
Pomenya nkhondo ndiponso
Wolanga kwabasi.
85. Amene angampemphere
(Mnzake) pempho labwino
(Lothandizira pazabwino)
adzapeza Gawo mmenemo. Ndipo
amene Angampempherere
pemphero Loipa, adzapeza gawo
m'zoipazo. Ndipo Mulungu
Ngodziwa chilichonse. 1
86. Ndipo pamene
mwalonjeredwa; Kulonjeredwa
kwamtundu uliwonse (Salam)
Vomerani ndi malonje abwino
oposa Amenewo, kapena Bwezani
ofanana Nawo. Ndithudi, Mulungu
Ngowerengera chinthu
chilichonse.
<g>
»ffi«
O&iJ
M'ndime iyi akuwalangiza anthu kuti azithandizana pazabwino zokha.
Azithandizana pazochita ndi zonena. Munthu akokere anzake kuzinthu
zabwino mmene angathere. lyenso mwini athandize ena pazinthu zabwino.
Akachita izi adzalandira mphoto yaikulu kwa Mulungu.
Surat 4. An-Nisa' Juzu 5
196
o *jfcl
t tl~jS\ $jj-»»
87. Mulungu! Palibe
wopembedzedwa Mwachoonadi
koma lye basi. Ndithudi,
Adzakusonkhanitsani tsiku
lachiweruzo Lopanda chikaiko
mwailo. Kodi ndi Mawu a ndani
angakhale oona Kuposa a
Mulungu?
88. Kodi mwatani inu pokhala
magulu awiri Pankhani ya
Amunafikina (achinyengo) Pomwe
Mulungu wawatembenuza
chifukwa (Cha zoipa) zomwe
achita? Kodi mukufuna Kuti
mumuongole amene Mulungu
wamlekerera Kusokera? Ndipo
amene Mulungu Wamsokeretsa,
simungathe kumpezera njira
(yomuikira kuchilungamo).
89. (Osakhulupirira a Chiarabu)
akufuna Kuti mukadakhala
osakhulupirira Monga momwe iwo
sadakhulupirire Tero kuti mukhale
ofanana. Musawachite kukhala
abwenzi Mpaka asamuke chifukwa
cha Chipembedzo cha Mulungu.
Koma Ngati anyoza, agwireni ndi
kuwapha Paliponse mwawapeza
(monga Momwe akukuchitirani
inu). Ndipo musamuyese mtetezi
Ngakhale mthandizi aliyense wa
iwo.
90. Kupatula omwe
akugwirizana Ndi anthu amene
pali pangano Pakati panu ndi iwo,
, J&&S\v)*&.{Jl$ %
Surat 4. An-Nisa'
Juzu 5
197 • *>»
i $.L-Ji *jj^
kapena Omwe akudza kwainu uku
zifuwa Zawo zili zobanika
kumenyana Nanu, kapena
kumenyana ndi Anthu awo.
(Oterewo musamenyane nawo).
Ngati Mulungu akadafuna,
Akadawakhwirizira painu,
choncho Akadamenyana nanu.
Ngati Atakupewani, osamenyana
nanu ndipo Nkukupatsani
mtendere, ndiye kuti Mulungu
Sadakupangireni njira paiwo
(yakuti Mumenyane nawo).
91. Muwapeza ena omwe
akufuna kupeza Mtendere kwa inu
ndi kupeza mtendere Kwa anthu
awo. Nthawi iliyonse
Akabwezedwa ku ukafiri (Ndi
anzawo osakhulupirira),
Amagweramo mwamtheradi
(nkuyamba Kumenyananso ndi
inu) ngati sadzipatula Kwa inu
ndipo osakupatsani Mtendere ndi
kutsekereza manja awo, Agwireni
ndi kuwapha paliponse pamene
Mwawapeza (monga momwe iwo
Akuchitira kwa inu) ndipo
Takupangirani chisonyezo
Choonekera pa iwo
92. Ndipo sikoyenera kwa
Msilamu kupha Msilamu (Mnzake
mwadala) pokhapokha mwangozi.
Ndipo yemwe wapha Msilamu
mwangozi, apereke Ufulu kwa
9' X*5VTV >\ £.t*»Ul »*<»'•
„9S 9t9 9j$. I 9 S 9?9\9&l' *? 99 % 9 <>
Surat4. An-Nisa' Juzu 5
198 « *>■
£ *L*Jl djj—»
kapolo wa Chisilamu ndi dipo
lomwe Alipereke kwa ofedwawo
pokhapokha akakana Okha
(amulowa mmalo a womwalilayo),
monga M'njira ya sadaka. Ngati
wophedwayo ndi Mnansi wa adani
anu pomwe ali Msilamu, Perekani
ufulu kwa kapolo wa Chisilamu,
(palibenso dipo lina). Ngati
wophedwayo ndi mmodzi Wa
anthu omwe pakati panu ndi Iwo
pali chipangano (chosamenyana
Nkhondo), ndiye kuti
amulowammalo Ake apatsidwe
dipo; Apatsidwenso ufulu kapolo
wa Chisilamu. Ndipo ngati
sadapeze (zoterozo), Asale miyezi
iwiri yotsatana. Iyo ndiyo Njira
yolapira (pautchimo Wotere)
yochokera kwa Mulungu. Ndipo
Mulungu Ngodziwa Ngwanzeru
zakuya.
93. Ndipo amene angaphe
Msilamu mwadala, Mphoto yake
ndi Jahanama; Mmenemo
adzakhala Muyaya. Ndipo
Mulungu amkwiira Ndi
kumtemberera ndi kumkonzera
Chilango chachikulu.
94. "E inu amene
mwakhulupirira! Mukayenda
Panjira ya Mulungu, musachite
chinthu Pokhapokha mutaonetsetsa
bwino. Ndipo Musanene kwa
amene akukulonjerani Salamu
Q®S&£
"*\£
U^jUuJI *j£\&f Uj^W>
Surat 4. An-Nisa' Juzu 5
199
O *>!
t ^L^Jl Ojj-*'
(kuti): "Sindiwe Msilamu,"
(Nkumupha). Mukufuna zinthu
Zamdziko lapansi komatu Kwa
Mulungu kuli zopeza zambiri.
Umo ndi momwe inunso mudalili
Kale; koma Mulungu
adakuchitirani Chifundo (choncho
mudalowa m'Chisilamu.
Penyetsetsani bwinobwino).
Ndithu, Mulungu Ngodziwa
bwinobwino Nkhani zonse zimene
muchita.
95. Sangafanane Asilamu omwe
Akukhala osapita kunkhondo
Pomwe sali ovutika, ndi amene
Akumenya nkhondo yoyera
Panjira ya Mulungu ndi Chuma
chawo ndi miyoyo yawo. Mulungu
wawatukula paubwino Ndi
paulemerero amene akuchita Jihadi
ndi chuma chawo ndi Miyoyo
yawo kuposa okhala. Koma
onsewo Mulungu wawalonjeza
Zabwino. Koma wawapambanitsa
Ochita Jihadi malipiro Aakulu
Kuposa ongokhala.
96. Adzapata ulemerero
waukulu ochokera Kwa iye ndi
chikhululuko ndi chisoni. Ndipo
Mulungu Ngokhululuka kwambiri,
Ngwachisoni zedi.
97. Ndithudi amene angelo
atenga miyoyo yawo, Ali
odzichitira okha zoipa
Surat 4. An-Nisa' Juzu 5
200
o *jA-i
t s-L-uil ^J-*'
(posasamuka ku
Makka),adzawauza kuti:
"Mudachitanji (Pachipembedzo
chanu?)" Iwo adzati: "Tidali
Ofooka ndi oponderezedwa
padziko: (Choncho Sitidathe
kuchita mapemphero Athu)."
(Angelo) adzati: "Kodi Dziko la
Mulungu silidali lotambasuka
kotero Kuti inu nkusamukira
kwinam'menemo?" Iwowo malo
awo ndi Jahanama. Taonani Kuipa
kwa malo obwelera. l
98. Kupatula omwe adali
ofooka Kwenikweni amuna Ndi
ana omwe sangathe kuchita Ndale
yamtundu uliwonse, ndipo
Sangathe kulondola njira (Yonkera
ku Madina).
99. Choncho iwo ndithudi
Mulungu Angawafafanizire, Pakuti
Mulungu ngofafaniza Machimo,
wokhululuka.
100. Ndipo amene angasamuke
panjira ya Mulungu (Chifukwa cha
®}jK*a* oA*o >^A>-
^ )f\ * ' '* 9' *' &'»**>? 9
(Ndime 97-9) Kalelo Mtumiki (SAW) atasamukira ku Madina pamodzi ndi
omtsatira ake Asilamu adawalamula kuti asamukire ku Madinako kusiya
nyumba zawo, chuma chawo, abale awo ndi ana awo. Izi zidali chonchi
chifukwa iwo akanakhalabe m'midzi yawo Pansi pautsogoleri wa anthu
osakhulupirira sakanatha kukwaniritsa malamulo a Chisilamu. Tero Chisilamu
chake sichikanakhala ndi ntchito. Ndipo Chisilamu chopanda ntchito si
Chisilamunso. Tero nchifukwa chake apa akuwadzudzula amene
sanasamuke kuti adzafa ndi imfa yoipa kupatula okhawo amene sanapeze
njira yosamukira ku Madina chifukwa chakufooka kwa matupi awo.Amenewa
madandaulo awo akhoza kuwavomera. Koma chachikulu nkuti ayesetse
kusamukira ku Madina.
Surat4. An-Nisa'
Juzu 5
201 • *>»
i s-L-Jl *jj**
chipembedzo chake,) apeza malo
Ambiri m'dzikomo othawira
ndikupeza bwino. Ndipo amene
angatuluke m'nyumba mwake kuti
Asamuke chifukwa cha Mulungu
ndi Mtumiki Wake, kenako
nkumpeza imfa (m'njira), ndithu,
Malipiro ake atsimikizika kwa
Mulungu. Ndithudi, Mulungu
ngokhululuka kwambiri,
Ngwachisoni chambiri. 1
101. Ndipo ngati mukuyenda
padziko, Sikulakwa kwainu
kufupikitsa Swala ngati mukuopa
kuti Angakusokonezeni omwe
Sadakhulupirire. Ndithudi,
Osakhulupirira ndi adani Anu
oonekera.
f
9 9 '\l9 9 S 9 9 u.^ si?" \<
e
Apa akuwalimbikitsa zakusamuka ndi kuwauza kuti kumene akupitako
akapeza bwino. Akuwalimbikitsanso okalamba ndi odwala kuti asamuke.
Ngati atafera panjira kuwerengedwa kuti adasamukabe ndipo adzapeza
mphoto yonga yayemwe adasamuka nkukakhala ku Madina pamodzi ndi
Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) ndi kukathandiza kukamenya
nkhondo yoteteza Chisilamu kwa adani. Ndi chimodzomodzi munthu akapita
ku Makka kukachita Haji ndipo nkumwalira Hajiyo asanachite, kapena
asanamalize zina zofunika pa Haji, kwa Mulungu amamuwerenga kuti wachita
mapemphero a Haji. Komabe abale ake akhoza kukamchitiranso
mapemphero a Haji.
2 Pamene Asilamu adawalamulira zakusamuka, adawafupikitsira Swala
chifukwa chamavuto am'njira monga kuti (a) Swala zokhala ndi raka zinayi
akhoza kuziswali ndi raka ziwiriziwiri. (b) Akhoza kuswali katatu kokha patsiku
m'malo mwakasanu.lzi zili motere: Swala ya Azuhuri nkuiphatikiza pamodzi
ndi swala ya Alasiri; kuzipemphera panthawi ya Azuhuri kapena
kuzipemphera panthawi ya Alasiri. Swala ya Magharibi nkuipemphera
pamodzi ndi swala ya Isha. Adzayamba kupemphera swala ya Magharibi raka
zitatu kenako nkupemphera Isha raka ziwiri. Koma swala ya Asubuhi yokha
njomwe imapempheredwa payokha ndiponso m'nthawi yake. Lamuloli
analikhazikitsa pamene Asilamu adali ndi mantha ndi masautso am'njira.
Ndipo Lidasiidwa momwemo losasinthika mpaka lero m'nthawi yomwe anthu
akukwera galimoto, sitima ndi ndege.
Surat4. An-Nisa' Juzu 5
202 • *>■•
t (tLmJI &jy
^9 «. >< "\ >4'l> >fVf KH * - /m
102. Ndipo ngati uli pamodzi
(ndi Asilamu Pankhondo)
ndikuwatsogolera Swala, Ndiye
kuti gulu limodzi laiwo liimirire
pamodzi ndi iwe ndikupemphera
uku Atagwirizira zida zawo. Ndipo
akamaliza kulambira kwawo, apite
kumbuyo Kwanu(kuti
akulondereni) ndipo lidze Gulu
lina lomwe silidapemphere,
lipemphere Nawe pamodzi;
nawonso achenjere Ndikugwirizira
zida zawo (nkupemphera),
Chifukwa chakuti omwe
sadakhulupirire akufuna kuti
mutanyalanyaza zida zanu Ndi
katundu wanu angokuukirani
Nthawi imodzi. Koma sikulakwa
kwainu Mutaika pansi zida zanu
chifukwa Chakuvutitsidwa ndi
mvula kapena ngati Mukudwala.
Koma chenjeranaoni. Ndithudi
Mulungu wawakonzera Chilango
choyalutsa osakhulupirira. 1
1 Swala yopemphera pagulu (jamaa) akuilimbikitsa zedi ngakhale kuti anthu
ali pakati pankhondo. Ngati nthawi ya swala yakwana akuwauza kuti
apemphere pagulu, koma asapemphere onse nthawi imodzi. Anthuwo
agawike m'magulu awiri. Gulu lina liyang'ane komwe kuli adani, ndipo gulu
lina likhale likupemphera pamodzi ndi (Imamu) mtsogoleri wawo. Komatu
Swala akunkhondo amaswali raka ziwiriziwiri (Swala ililonse) kupatula Swala
ya Magharibi.
Tsono Imamu adzapemphera raka imodzi ndi awo omwe akupemphera nawo.
Akaimirira kuti apemphere raka yachiwiri.aja omwe anali kupemphera naye
aimilire ndi kupemphera raka yotsalayo mwachangu atamsiya imamu ali
chiimirire. Ndipo apite kukalowa m'malo mwa anzawo omwe anali kuyang'ana
komwe kuli adani. Tsono anzawowo adze nkudzapemphera ndi Imamu.
Imamu akamaliza raka yake yachiwiri, iwo aimirire nkumaliza raka yawo
yachiwiri. Komatu popempherapo zida zawo zikhale atazikoleka m'matupi
Surat 4. An-Nisa'
Juzu 5
203
o *j*-i
1 i-L-Jt *JJ-"
103. Mukamaliza Swala,
pitirizani kumkumbukira Mulungu
muli chiimire, chikhalire kapena
Mutagona chammbali. Ngati
mutapeza Chitetezo (chifukwa
chakuti nkhondo palibe),
Pempherani Swala zanu mwa
chilamulo. Ndithudi, Swala
ndilamulo lokhala ndi Nthawi kwa
Asilamu. 1
104. Ndipo musachite ulesi
kutsata anthu (omwe Ndi adani),
ngati mukumva kupweteka,
Iwonso akumva kupweteka monga
momwe inu Mukumvera
kupweteka. Koma inu
Mukuyembekezera kwa Mulungu
Chomwe iwo sakuyembekezera.
Ndipotu Mulungu Ngodziwa:
Ngwanzeru. 2
105. Ndithudi,
takuvumbulutsira Buku Mwa
choonadi kuti uweruzire pakati Pa
anthu, monga momwe Mulungu
Wakuphunzitsira. Ndipo usakhale
Mtetezi wa achinyengo.
mwawo pokhapokha ngati pali zifukwa zoikitsa zidazo pansi, zomwe azitchula
kumapeto a ndimeyo
1 Nkofunika nthawi zonse Msilamu kukumbukira Mulungu, osati panthawi
yokha yopemphera koma amkumbukire m'chikhalidwe chake chonse ndi
m'zochita zake zonse. Nthawi zonse apewe zomwe Mulungu waletsa ndi
kutsata malamulo ake.
2 Apa akuwalamula Asilamu kuti amenyere chipembedzo chawo ngakhale
atapeza mavuto amtundumtundu. Chifukwa chomwe akupezera mavutowo
nchachikulu zedi kuposa mavutowo palibe chinthu chachikulu chimene
munthu angachipeze chabe popanda kuvutikira.
Surat 4. An-Nisa'
Juzu 5
204
o *£\
t tL^Jl djj**»
106. Ndipo mpemphe
chikhululuko Mulungu. Ndithudi,
Mulungu Ngokhululuka kwabasi,
Ngwachisoni chambiri.
107. Ndipo usawaikile
kumbuyo omwe Akudzichitira
okha chinyengo. Mulungutu
sakonda yemwe ali Wachinyengo,
wamachimo.
108. Akudzibisa kwa anthu
(pochita za Machimo) koma
sakuzibisa kwa Mulungu pomwe
lye adali nawo Pamodzi pamene
adali kupangana Usiku mawu
osakondweretsa. Mulungutu
Akudziwa bwinobwino zimene
akuchita. 1
109. Taonani! Inu ndi amene
mwaayikira Kumbuyo pamoyo
wapadziko lapansi. Kodi ndani
amene adzatsutsana ndi Mulungu
pa iwo tsiku lomaliza, Kapena
ndani adzakhale Mtetezi wawo. 2
\j&-gg&\&$bb$z$
1 Anthu achiphamaso amabisa zochita zawo kwa anthu kuti asazione. Koma
salabadira kuonedwa ndi Mulungu pomwe Mulungu Njemwe adzawalipira.
Pomwe Mulungu akudziwa zonse zimene zikuyenda m'mitima mwawo
ndiponso akumva ndi kuziona zonse zimene akuchita. Kunali kofunika kwa
iwo kumuopa Mulungu amene ali ndi mphamvu zochitira chilichonse chimene
wafuna.
2 M'ndime iyi Mulungu akuletsa anthu kuti asakhalire kumbuyo anthu oipa
koma awaleke kuti awalange chifukwa chazoipa zawo ndi kuti amene
adamuchitirapo zoipa apeze bwino muntima mwake. Choncho aweruzi amilandu
achenjere kukhalira kumbuyo anthu oipa omwe ali nawo chitsimikizo kuti
adachenjerera anzawo. Asaone ulemerero wamunthu mmene ulili ngakhale
ali ndi chuma chotani. Koma m'malomwake akhalire kumbuyo amene ali
oponderezedwa. Akatero adzapeza mphoto yomwe Mulungu walonjeza
chifukwa chakusonyeza choonadi poyera. Aweruzi akagwira njira imeneyi
ndiye kuti adzapambana pano padziko lapansi mpaka patsiku lachiweruzo.
Surat 4. An-Nisa' Juzu 5
205
*jJU|
t *L«%Jl QjJ~*
110. Ndipo amene angachite
choipa (povutitsa Ena), kapena
kudzichitira yekha zoipa Ndipo
kenako nkupempha chikhululuko
kwa Mulungu, adzampeza
Mulungu ali Wokhululuka,
Kwabasi,Wachisoni kwambiri. 1
111. Ndipo amene angachite
tchimo, ndiye kuti Akudzichitira
yekha. Mulungu Ngodziwa,
Ngwanzeru zakuya. 2
112. Ndipo amene angachite
cholakwa (Chaching'ono) kapena
tchimo (Lalikulu) kenako
nkumponyera Nalo yemwe
sadalakwe momunamizira,
Ndithudi, wasenza bodza lalikulu
Lamkunkhuniza ndi uchimo
woonekera.
113. Ndipo pakadapanda
ubwino wa Mulungu ndi chisoni
chake paiwe, Ndithudi, gulu
limodzi laiwo Likadalinga
[0 9 ^
foi'^/fl't^V.
Mulungu akuwalimbikitsa ochimwa: (a) Kuti atembenukire kwa lye
mwachangu ndi kusiya zimene akuchitazo. (b) Atsimikize mumtima kuti
sadzachitanso uchimowo. (c) Adandaule pauchimo umene adauchitawo. (d)
Awabwezere eni zinthu zomwe adazitenga mwachinyengo. (e) Akawapemphe
kuti awakhululukire. Akakwaniritsa zonsezi ndiye kuti kulapa kwawo Mulungu
akuvomera.
2 M'ndime iyi akuti munthu wochitira anthu anzake zoipa, akudzipha yekha
pakuti Mulungu sadzamleka koma amkhaulitsa pompano padziko lapansi
kapena pakutha kwadziko.
3 Pali anthu ena amene amaukwera uchimo. Kenako nkumanamizira wina
wake. Munthu wamakhalidwe awa, chiweruzo chake chidzakhala choopsa
tsiku lomaliza, ngakhale wadzipulumutsa pano padziko lapansi chifukwa
chakuthyathyalika kwake. Kapena pompano padziko lapansi amachiona
chomwe chinameta nkhanga mpala.
Surat4. An-Nisa'
Juzu 5
206 * *>»
i tL-Jl Sjj-*»
kukusokeretsa. Ndipo Iwo palibe
yemwe akadamsokeretsa Koma
iwo okha basi. Ndipo sangathe
Kukuvutitsa ndi chilichonse. Ndipo
Mulungu wakuvumbulutsira
Buku, Kudzanso luntha. Ndipo
wakuphunzitsa Zomwe sudali
kuzidziwa. Ndipo ubwino wa
Mulungu umene uli paiwe
ngwaukulu zedi.
114. Palibe ubwino m'zambiri
zimene Akunong'onezana kupatula
amene Akulamulira ena kupereka
sadaka, Kapena kuchita zabwino,
kapena Kuyanjanitsa pakati pa
anthu (Pakunong'onezana mawu).
Amene Angachite
zimenezi,chifukwa chofuna
Chiyanjo cha Mulungu,
tidzampatsa Malipiro aakulu.
115. Ndipo amene anyoza
Mtumiki Pambuyo pomuonekera
chiongoko Nkutsata njira
yosakhala ya Asilamu,
Timtembenuzira kumene
Watembenukira mwini wakeko.
Ndipo tidzamulowetsa ku
Jahanama. Taonani kuipa malo
ofikira.
Apa Mulungu akunena kuti palibe chisomo chimene Mulungu wapatsa
munthu chachikulu ndi chopindulitsa kuposa luntha. Chilichonse chabwino
chapadziko lapansi ndi pa tsiku lachimaliziro chimapezeka chifukwa cha
kudziwa zinthu. Qur'an yonse ndi hadisi za Mtumiki zikulimbikitsa
zakufunafuna luntha lodziwira zinthu zakuti zimkonzere munthu zadziko
lapansi ndi za tsiku lachimaliziro, kotero kuti Qur'an ndi hadisizo zikunena kuti
munthu apite kunja kunka nafunafuna maphunziro.
Surat4. An-Nisa 9 Juzu 5
207
*jJrl
t s-L-Jl £jj-"
116. Ndithudi, Mulungu
sakhululuka (utchimo)
Womphatikiza ndi chinthu china,
(pochiyesa Kuti ndi mnzake wa
Mulungu). Koma lye
Amakhululukira matchimo ena
omwe sali Amenewo kwa yemwe
wamfuna. Ndipo yemwe
Angamphatikize Mulungu (ndi
milungu yabodza), Ndithudi,
wasokera; kusokera konka nako
kutali (Ndi njira yachoonadi).
117. Sapembedza Mulungu
koma Mafano achikazi, ndiponso
Sapembedza china koma satana
Wonyoza (wamatchimo)
118. (Yemwe) Mulungu
adamtemberera. Ndipo lye
(Satana) adati (kwa Mulungu):
"Ndithudi, ndikadzipezera gawo
lodziwika Mwa akapolo anu;" 1
119. "Ndikawasokeretsa ndi
kuwapatsa Ziyembekezo (zabodza)
ndithu Ndikawalamula kuti
azikadula makutu A ziweto, ndipo
ndikawalamulanso Kuti
azikasintha chilengedwe cha
Mulungu." Ndipo amene
angamulole Satana kukhala
9. 9 *" a S\ ' 9 u" 9 1 9 •* V» 'i» I £ I
9 W' >&' 99%"*'i\'99<i% .Vftf
Iblis pamene adampirikitsa kumwamba iye adauza Mulungu kuti
akazikometsera zolengedwa zake matchimo. Mulungu adamuuza kuti
sangathe kuzisokereza mwamphamvu, mozikakamiza, zifune zisafune.
Aljyense amene akamtsata ndiye kuti akamtsata mwachifuniro chake.
Sikuti mogonjetsedwa ndi mphamvu za Satana kotero kuti iye sangathe
kulimbana naye iyayi. Satana alibe mphamvu zokakamizira anthu.
Surat4. An-Nisa'
Juzu 5
208
*j*-\
t s-l^Jl ^J-**
mtetezi wake kusiya
Mulungu,ndiye kuti wataika
koonekera. l
120. (Satana) akuwalonjeza
ndikuwapatsa chiyembekezo
(Pazinthu zomwe sizingachitike).
Ndithudi, Satana sawalonjeza
china koma Chinyengo basi.
121. Iwowo malo awo ndiku
Jahanama;ndipo sadzapeza
Pothawira kutuluka mmenemo.
122. Ndipo omwe akhulupirira
ndi Kumachita zabwino,
tidzawalowetsa Ku minda yomwe
pansi ndi patsogolo Pake mitsinje
ikuyenda. Adzakhala M'menemo
muyaya. Hi ndilonjezo Loona la
Mulungu. Kodi ndani woona
Ponena kuposa Mulungu?
123. (Kulowa ku Munda
Wamtendere) sikuli Pakukhumba
kwanu ngakhalenso pakukhumba
Kwa anthu a Buku. (Koma kuli
^^^W
(©Lag^l^
1 Apa akutchula zlna mwazinthu zomwe Satana adzasokeretsa nazo anthu:
(1) Kukhala ndi chiyembekezo choti Mulungu adzawakhululukira pakuti iye
ngokhululuka, Ngwachifundo. (2) Kuti ukachita zakutizakuti kapena
ukawerenga duwa yakutiyakuti machimo ako onse adzakufafanizira ngakhale
kuti udakwatula zinthu za anthu. (3) Kuti wolemekezeka uje adzatiwombola
ngati tilumikizana naye. (4) Kuti mneneri wakutiwakuti adzaitana omtsatira ake
kuti akalowe kumunda wamtendere. (5) Kuti Mtumiki sadzakhala wokondwa
kuona anthu ake akuponyedwa kumoto. (6) Kukhala ndi chiyembekezo choti
ngati munthu ndiwe Msilamu basi sukalowa ku Jahanama.
Ndipo Satanayu amanyenganso Akhrisitu kuti ngati akhulupirira Yesu basi
sakalowa kumoto. Ndipo Ayuda amawauzanso chimodzimodzi kuti ngati
akhulupirira m'chipembedzo cha chiyuda sakalowa kumoto. Nawonso
opembedza moto ndi Abudha amawauzanso chimodzimodzi kuti ngati atsata
chibudha basi apulumuka.
Surat 4. An-Nisa' Juzu 5 209 ° *>'
t s-L-Jl ^JJ-"
pakulungama Ndi kuchita zomwe
Mulungu afuna). Amene angachite
choipa, adzalipidwa (nacho) Ndipo
sadzapeza mtetezi Ngakhale
mpulumutsi kupatula Mulungu.
124. Ndipo amene angachite
ntchito zabwino, mwamuna
Kapena mkazi, pomwe iye ali
wokhulupirira, Iwo ndi amene
adzalowa kumunda Wamtendere.
Ndipo sadzaponderezedwa
chilichonse choipa, Ngakhale
chochepetsetsa kwambiri ngati
Kamphako ka nthangala ya tende
125. Kodi ndani yemwe ali ndi
chipembedzo Chabwino choposa
yemwe walunjika Nkhope yake
kwa Mulungu, iye ali Wabwino
ndipo akutsata njira ya Ibrahim
Woona pa chikhulupiriro. Ndipo
Mulungu Adasankha Ibrahim
kukhala bwenzi
126. Ndipo zonse zakumwamba
ndipansi nza Mulungu; ndipo
Mulungu ndi amene Wazungulira
chinthu chilichonse kuchidziwa.
127. Ndipo akukufunsa zomwe
zikukhudza Azimayi nena:
"Mulungu akukuuzani Nkhani za
iwo ndi zomwe zikuwerengedwa
Kwa inu m'Buku (ili) zaakazi
amasiye Omwe simukuwapatsa
(chiwongo chawo) Chomwe
chidalamulidwa kwa iwo,
"W*} A* - ' <y*3 ^ii (y—»-l fcr«j
Surat4. An-Nisa' Juzu 5
210 • «■>■•
£ frU*Ujl CjJ-"'
komabe Mukufuna kuwakwatira
ndi za ana omwe Ali ofooka ndi
oponderezedwa; ndipo
(Akukuuzani) kuti limbikirani
kuwayang'anira Ana amasiye
mwachilungamo. Ndipo Chabwino
chilichonse chimene muchita,
Mulungu akuchidziwa. '
128, Ndipo ngati mkazi ataona
kuti ndi Mwamuna wake
akukanganakangana Ndi
kupatulana, palibe kulakwa pa iwo
Kuyanjana pakati pawo
mwachimvano. Ndipo chimvano
ndichabwino. (Munthu Aliyense
amaumirira chimene afuna).
Chifukwa chakuti mitima ya anthu
imaumirira Umbombo. Koma ngati
muchita zabwino Ndi kuopa
Mulungu, ndithudi, Mulungu
Ngodziwa nkhani zanu zonse
zomwe muchita.
129. Ndipo inu simungathe
kuchita chilungamo (Chenicheni)
pakati pa akazi ngakhale
Mutayesetsa chotani. Koma
musapendekere (Mbali imodzi);
kupendekera kwathunthu kotero
Kuti nkumusiya (yemwe
simukumfunayo) ngati Kuti
wapachikidwa (osadziwika kuti
ngokwatiwa Kapena ayi). Ndipo
ngati mutayanjana ndi Kuopa
e^l^w^SGW
1 Mukuuzidwa nkhanizi zomwe akuwerengerani mu ndime ya 2 ndi 12 M'sura
yomweyi .
Surat4. An-Nisa' Juzu 5
211 • »>»
t $.L*Jt *J>^
Mulungu (zingakhale bwino).
Ndithudi, Mulungu Ngokhululuka
kwambiri, Ngwachisoni Zedi.
130. Koma ngati atalekana,
Mulungu angalemeretse Aliyense
waiwo kuchokera m'zabwino Zake
Zochuluka ndipo Mulungu ali nazo
zambiri, Ngwanzeru zakuya.
131. Zonse zakumwamba ndi
pansi nza Mulungu. Ndithudi,
tidawalangiza omwe Adapatsidwa
buku patsogolo panu ndi Inunso
kuti muopeni Mulungu. Koma
ngati mungakane, ndithudi, zonse
Zakumwamba ndi pansi nza
Mulungu. Ndipo Mulungu
Ngokhupuka kwabasi
Wotamandidwa.
132. Zonse zakumwamba ndi
pansi nza Mulungu; ndipo
Mulungu akukwana Kukhala
mtetezi (kwa anthu Ake).
133. Ngati atafuna,
akuchotsani, Inu anthu, ndi
kubweretsa ena. Ndipo Mulungu
ali wokhoza Pazimenezo.
134. Amene afuna mphoto
yadziko lapansi, (Afunefune kwa
Mulungu). Kwa Mulungu
Ndikumene kuli mphoto yapadziko
lapansi ndi Ya tsiku lomaliza.
Ndipo Mulungu Ngwakumva,
Ngopenya.
Surat4. An-Nisa' Juzu 5
212
*jJU|
i $.L*Jl ojj-**
135. "E inu amene
mwakhulupirira! Khalani Oimiritsa
chilungamo, opereka umboni
Chifukwa cha Mulungu; ngakhale
kuti Ubwere ndi masautso kwa inu,
kapena kwa Makolo anu, kapena
kwa abale anu, ngakhale Ali
olemera kapena osauka,
(musayang'ane Zimenezo).
Mulungu ndiye woyenera
kuyang'ana Za awiriwo. Choncho
musatsate zilakolako Ndi kusiya
chilungamo. Ngati mukhotetsa
(Umboni), kapena kupewa
(kupereka Umboni) ndithudi
nkhani zonse zomwe Mukuchita
Mulungu akuzidziwa.
136. "E inu amene
mwakhulupirira! Khulupirirani
Mulungu ndi Mtumiki Wake, ndi
Buku lomwe analivumbulutsa Pa
Mtumiki Wake, ndi mabuku
Omwe adawavumbulutsa kale.
Ndipo amene akane Mulungu,
Angelo Ake, mabuku Ake, atumiki
Ake ndi tsiku lomaliza,ndiye kuti
wasokera; Kusokera konkera nako
kutali.
137. Ndithudi, amene
adakhulupirira, Kenako
nkusakhulupirira,
Nadzakhulupiriranso, kenako
Nkusakhulupiriranso, naonjezera
Kusakhulupirira, Mulungu
Sadzawakhululukira, ndipo
$&&%&&*&$&
$$*&#&$&&&
&%?$&$&
Surat4. An-Nisa' Juzu 5
213
o *>i
£ *L*Jt Sjj-*'
Sadzawawongolera m'njira
(yabwino)
138. Auze Amunafikina
(Achiphamaso) kuti Adzapeza
chilango chowawa;
139. (Achiphamaso) omwe
amaachita Osakhulupirira kukhala
abwenzi Awo kusiya Asilamu.
Kodi Akufuna kupeza ulemerero
kwa iwo? Ndithudi ulemerero
wonse ngwa Mulungu; (suli
m'manja mwa anthu).
140. Ndithudi lye
wakuvumbulutsirani m'Buku (ili)
kuti Mukamva maaya (ndime) a
Mulungu akukanidwa ndi
Kuchitiridwa chipongwe,
musakhale pamodzi nawo Mpaka
alowe m'zokamba zina. (Ngati
mutakhala Nawo) ndiye kuti
mukhala chimodzimodzi ndi iwo.
Ndithudi, Mulungu
adzawasonkhanitsa Achiphamaso
ndi osakhulupirira onse m'moto
wa Jahanama.
141. (A chiphamaso) omwe
akukuyembekezerani (kuti Mavuto
akugwereni), ngati mutapeza
kupambana Kochokera kwa
Mulungu, amakuuzani "Kodi
sitidali nanu limodzi?" Koma ngati
Osakhulupirira atapeza gawo
(lopambana), Amanena (kwa
osakhulupirira;) "Kodi
Sitidayandikire kukugonjetsani
©^l^&t^!^
■U#
Surat 4. An-Nisa' Juzu 5
214
a *jJUl
t $.L*Jl <*JJ~**
pamene Tidali M'gulu lankhondo
la Asilamu koma
Timakutsekerezani kwa Asilamu?"
Koma Mulungu adzaweruza pakati
Panu tsiku lachiweruzo. Ndipo
Mulungu Sangawaikire njira
osakhulupirira pa Asilamu (kuti
awagonjetse kotheratu).
142. Ndithu, achiphamaso
akufuna kunyenga Mulungu Koma
lye awalanga (chifukwa cha
chinyengo Chawocho). Ndipo
akaimirira kupemphera Swala,
amaimirira mwaulesi
ndikungoonetsa anthu (Kuti
akupemphera). Ndipo satchula
Mulungu Koma pang'ono pokha.
143. Akungoyendayenda pakati
pa awa ndi awa (Pakati pa Asilamu
ndi osakhulupirira). Iwo Sali mbali
iyi kapena mbali inayo. Ndipo
Amene Mulungu wamlekerera kuti
asokere Sungampezere njira
yolungama.
144. "E inu amene
mwakhulupirira! Musawachite
osakhulupilira kukhala Abwenzi
ami kusiya okhulupirira (Asilamu)
kodi mukufuna Kuti Mulungu
akhale ndi Mtsutso woonekera
painu (Kuti ndinu oyipa?)"
145. Ndithu achiphamaso
Adzakhala pansi penipeni Pamoto;
ndipo sudzampeza Mthandizi
woimira iwo.
Surat4. An-Nisa'
Juzu 6
215
1 *j*-»
£ *L«Jt ^JJ- -
146. Kupatula amene alapa
(pambuyo pa Chiphamaso chawo);
nakonza (makhalidwe Awo)
nadziphatika kwa Mulungu;
Namuyeretseranso Mulungu
Nchipembedzo chawo. Choncho
iwo Ali pamodzi ndi Asilamu.
Ndipo Mulungu adzapatsa
Asilamu malipiro akulu.
147. Mulungu sangakulangeni
ngati Mumthokoze ndi
kumkhulupirira. Ndithudi,
Mulungu Ngolandira Kuthokoza
kwanu, ndiponso Ngodziwa.
148. Mulungu sakonda
kutulutsa Mawu ofalitsa kuipa
(kwa anthu) Kupatula yekhayo
wachitiridwa zoipa. Ndipo
Mulungu Ngwakumva,
Ngodziwa. 1
149. Ngati mungaonetse
chabwino, Kapena kuchibisa,
kapena Kukhululukira zoipa,
(zoterozo Ndizo zofunika) ndithu
Mulungu Ngokhululuka ndiponso
Ngokhoza.
150. Ndithudi amene
sakhulupirira Mulungu ndi
Atumiki Ake, ndikufuna
kumlekanitsa Mulungu Ndi
@\$p£\ji\
1 Indedi, Mulungu sakonda anthu ofalitsa zoipa za anzawo popanda choipa
chilichonse chimene awachitira. Koma munthu amene ena amchitira choipa
akumlola kutchula kuipa komwe ena amchitira pokamnenera kwa muweruzi
kuti muweruziyo amuthandize paamene amchitira zoipawo. Koma kulengeza
kuipa kwa anthu ena nkosaloledwa m'chisilamu. Ndipo ndi utchimo waukulu.
Surat4. An-NisS'
Juzu 6
216 1 *>■»
t S-L*lJl 5jJ-*»
atumiki Ake, ponena kuti: "Ena
Tikuwakhulupirira, koma ena
tikuwakana", ndipo Akufuna
kugwira njira yapakati pa izi
(Osati ya Chisilamu chenicheni
kapenanso ya Anthu
osakhulupirira). 1
151. Iwo ndiwosakhulupirira
Enieni. Ndipo osakhulupirira
Tawakonzera chilango Choyalutsa.
152. Ndipo amene akhulupirira
Mulungu Ndi atumiki ake,
nkusamulekanitsa Aliyense waiwo
(koma nkwakhulupirira Onse), iwo
adzawapatsa malipiro awo. Ndipo
Mulungu Ngokhululuka
Kwambiri, Wachisoni zedi.
153. Anthu amene adapatsidwa
Buku (Ayuda) akukupempha (Iwe
Mtumiki) kuti uwatsitsire Buku
kuchokera Kumwamba. Ndithudi,
adampemphanso Musa zazikulu
Kuposa zimenezi pomwe adati:
"Tiwonetse Mulungu Poyera".
Ndipo udawagwira moto
wamphenzi (umene Udachotsa
* A 9 '
J
99 9 ~%* IV *'e* < 9 *u 9S<? V
Aliyense mwa anthu yemwe Mulungu wamuvomereza kuti ndi mtumiki
Wake, ndipo iwe nkukana kumkhulupirira, monga Ayuda mmene amamkanira
Mneneri Yesu, ndi Akhrisitu mmene amamkanira Mneneri Muhammad (SAW),
kutereko nkusakhulupirira Mulungu. Asilamu amavomereza Aneneri onse
oona amene adadza Muhammad (SAW) asadabadwe. Asilamu akuvomereza
aneneri onse monga momwe Mulungu wafotokozera n'Qur'an. Ndipo
savomereza omwe Mulungu sadawavomereze kuti ndi Aneneri ake. Oterewa
ndi amene akunama kuti adapatsidwa uneneri pambuyo pa Mneneri
Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale naye) monga Mirza Gulam
Ahmad ndi Bahai. Amene akukhulupirira amenewa ndiye kuti ngopandukira
Mulungu. Tero tichenjere ndiudyerekezi wa Akadiani ndi Abahai ndi ena otere.
Surat4. An-Nisa' Juzu 6
217
% frjA-i
t ti—Ji ojj— *
miyoyo yawo chifukwa
chakusakhulupirira Kwawo.
Zitatero Mulungu adawapatsa
moyo kachiwiri). Ndipo kenako
iwo adapanga thole (mwana
wang'o mbe Monga Mulungu
wawo) pambuyo powafikira
Zisonyezo zoonekera. Koma
tidawakhululukira Zimenezo,
ndipo tidampatsa Musa zisonyezo
Zooneka. 1
154. Ndipo tidatukula phiri
pamwamba pawo (Ayudawo)
polandira pangano lawo; Tidati
kwa iwo: "Lowani pachipata
(Chadziko ili la Shamu)
mutawerama". Tidatinso kwa iwo:
"Musalumphe Malire (pochita
usodzi) tsiku la Sabata". Ndipo
tidalandira kwaiwo Pangano
lokhwima.
®\£^^)al£
1 Ayuda adauza mtumiki Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale naye)
kuti sangakhulupirire pokhapokha amuone akukwera kumwamba popanda
kugwirira chilichonse ndi kubwera pansi pano Buku lili m'manja mwake
mutalembedwa umboni wa Mulungu woti iye Muhammad ndi Mtumiki
Wakedi. Ndipo Mulungu akuti makhalidwe otsutsana ndi Aneneri siachilendo
kwa Ayuda. Ndipo Musa atalephera kuchita zimenezo adamuda. Tero
adapanga fano (lamwana wang'ombe 'thole') naliyesa Mulungu wawo.
2 (Ndime 154-6) Mulungu akupitiriza kufotokoza zoipa zawo. Ndipo zina
mwaizo ndiizi:
(a) Adakana kutsatira malamulo am'Taurat. Ndipo Mulungu adazula phiri
naliimitsa pamwamba pamitu yawo nawauza kuti: "Ngati simulola kulonjeza
kuti mdzatsata zomwe zili m'Taurat, likusinjani phiri ili.
(b) Adakana kulowera pachipata kudziko la Shamu Kenani monga momwe
Mulungu adawalangizira. Ndipo adalowa monga momwe iwo amafunira.
Shamu ndi dziko lomwe Mulungu adawapatsa kuti akalowemo ndi kukhazikika
pambuyo posamuka ku Eguputo (Egypt). Koma iwo sadathokoze chisomochi
potsata zomwe Mulungu adawauza.
Surat4. An-Nisa'
Juzu 6
218 1 ►>■•
£ *L«Jl Sjj**
155. Choncho (tidawalanga)
chifukwa chakuswa Mapangano
awo, ndi kukana kwawo zisonyezo
Za Mulungu, ndi kupha kwawo
aneneri popanda Choonadi, ndi
kunena kwawo kwakuti, "Mitima
yathu yakutidwa (siingathe
kuzindikira Zomwe ukunena iwe
Muhammad {SAW})". ( Ai,
Siinakutidwe ndi chilichonse),
Koma Mulungu Waidinda zidindo
chifukwa chakusakhulupirira
Kwawo; tero sakhulupirira koma
pang'ono pokha.
156. Chifukwa
chakusakhulupirira kwawo ndi
Kumnamizira kwawo Maria bodza
lalikulu (Kuti wabala Yesu m'njira
yachiwerewere);
^mzK^stfb
(c) Pambuyo polowa m'dzikolo adawauza kuti alemekeze tsiku la Sabata kuti
likhale tsiku lamapemphero okhaokha. Lisakhale tsiku logwira ntchito. Koma
iwo adachitachita ndale zawo mpaka lidasanduka tsiku logwira ntchito.
(d) Ena mwa aneneri awo pamene adawaletsa iwo machitidwe amenewa
mwaukali.adawapha.
(e) Mneneri Muhammad pamene adawafotokozera zizindikiro zomwe zinali
m'mabuku mwawo zimene zimasonyeza utumiki wake sadamulabadire.
"Mitima yathu yakutidwa. Siikumvetsa chilichonse chimene ukunena".
(0 Mneneri Yesu pamene adawafotokozera za utumiki wake ndi
kuwasonyeza zozizwitsa ndi zonse zomwe zidachitika m'kubadwa kwake, iwo
adati Mayi Maria adatenga pakati m'njira yachiwerewere pomwe iwo
amadziwa kuti akungonama.
(g) Adakonza chiwembu kuti aphe Yesu. Koma Mulungu adachiononga
chiwembu chawocho pomuveka munthu wina nkhope ya Yesu amene adali
wamkulu wawo yemwe ankafunisitsa kupha Yesu. Tero adampachika
mnzawoyo pamtanda. Pambuyo pake, akuluakulu aChiyuda adazindikira
zonse zomwe zidachitikazi. Ndipo adangonyozera ngati kuti sichidachitike
chilichonse chododometsa chifukwa choopa kuti anthu angawaukire.
M'malomwake ankangodzidzudzula okha m'mtima mwawo.
Siirat 4. An-Nisa' Juzu 6 | 219 t ^
t *.L-*Jl SjJ-*'
157. Ndikulankhula kwawo
(kwakuti) "Ife tamupha Mesiya
Yesu mwana wa Maria, Mtumiki
wa Mulungu; Koma sadamuphe
ndipo sadampachike Pamtanda.
Koma adasokonezedwa (ndi
munthu Wina namuganizira kuti
ndi Yesu). Ndithudi, Amene
akutsutsana pankhani
(yakuphedwa kwake) Ali
m'chikaiko ndi kuphedwa kwake;
alibe kudziwa Kotsimikizika,
koma akungotsatira
Zongoganizira. Ndithudi,
sadamuphe.
158. Koma Mulungu
adamkweza Kwa lye ndipo
Mulungu Ndimwini mphamvu
zoposa, Ngwanzeru zakuya.
159. Palibe aliyense mwa anthu
omwe adapatsidwa Buku (Ayuda
ndi Akhrisitu amene Amamwalira
asanazindikire za momwe Yesu
Adalili); koma amamzindikira
ndithu (kuti Sadali Mulungu)
patangotsala pang'ono Kumfikira
imfa yake. (Nayenso Yesu) pa
Tsiku lachiweruzo adzaikira
umboni paiwo (Kuti iye adali
chabe kapolo wa Mulungu).
160. Chifukwa chakuchita
kwawo zoipa, awo Ayuda,
tidaletsa kwa iwo zinthu zabwino
(Zakudya)zomwe zidali
e^SM6«ri*«a^
Surat 4. An-Nisa' Juzu 6
220
1 *>»
t s-L-Jl 0jj«*»
zovomerezeka kwa iwo; Ndiponso
chifukwa chakutsekereza kwawo
Anthu ambiri kuyenda panjira ya
Mulungu.
161. Ndi kudya kwawo riba
(katapira) pomwe Adaletsedwa
kuti asadye; ndiponso chifukwa
Chakudya kwawo chuma cha
anthu Mwachinyengo. Ndipo
osakhulupirira mwa Iwo
tawakonzera chilango chopweteka.
162. Koma mwaiwo amene
azama pamaphunziro, Ndi Asilamu
(onsewo) akukhulupirira zimene
Zavumbulutsidwa kwa iwe ndi
zimene Zidavumbulutsidwa
patsogolo pako. Ndipo omwe
akupitiriza Kupemphera swala,
ndikupereka Zakati, ndi
kukhulupirira mwa Mulungu ndi
tsiku lomaliza, Iwo tidzawapatsa
malipiro akulu.
163. Ndithudi,
takuvumbulutsira (chivumbulutso)
Monga momwe
tidamuvumbulutsira Nuhu (Nowa)
ndi aneneri amene anadza
pambuyo pake. Ndipo
tidavumbulutsiranso Ibrahim,
Ismael, Ishaaq, Yakub ndi
mbumba yake. Ndipo
(tidavumbulutsiranso) Isa, Ayub,
Yunusu, Haarun ndi Sulaiman,
ndipo Daudi Tidampatsa Zabur
(Masalimo).
©j^
hV*'-^
Surat4. An-Nisa'
Juzu 6
221
n *>»
i *.L«Ji 5jj-*>
164. Ndipo (tidavumbulutsanso
chivumbulutso) Kwa aneneri
omwe takusimbira kale (nkhani
Zawo) ndi aneneri ena omwe
sitinakusimbire (Nkhani zawo);
ndipo Mulungu adayankhula Ndi
Musa mwachindunji.
165. (I wo ndi) aneneri omwe
adauza nkhani zabwino (Kwa
anthu abwino) ndi kuwachenjeza
(oipa) Kuti anthu asadzakhale ndi
mtsutso pa Mulungu Pambuyo pa
(kudza kwa) aneneriwa. Ndipo
Mulungu Ngwamphamvu zoposa,
Ngwanzeru zakuya.
166. Koma Mulungu akuikira
umboni zimene Wakuvumbulutsira
(kuti nzoona) Adavumbulutsa
mwanzeru Yake. Nawonso angelo
akuikira umboni. Ndipo Mulungu
akukwana kukhala mboni.
167. Ndithu, amene
sadakhulupirire, naletsa (Anthu)
kuyenda panjira ya Mulungu,
Ndithudi, asokera; kusokera
Komka nako kutali.
168. Ndithudi, amene
sadakhulupirire, Namachita zoipa,
kwa Mulungu Sipadzakhala
kuwakhululukira Ngakhale
kuwatsogolera njira.
169. Kupatula njira yomka ku
Jahanama Mmenemo akakhala
9 Iff 9)\* '<>*&& 9*'
Surat4. An-Nisa'
Juzu 6
222 1 *>»
i tt~Jl Sjj-*
muyaya. Ndipo zimenezo
nzopepuka Kwa Mulungu.
170. E inu anthu! Mtumiki
(Muhammad{SAW})
Wakudzerani ndi choonadi
Chochokera kwa Mbuye wanu.
Choncho Khulupilirani; ndi bwino
kwa inu kutero. Koma ngati
mukana, (dziwani kuti) zonse
Zakumwamba ndi zapansi nza
Mulungu; (Palibe chomwe
angaluze Pakusakhuluprira
kwanu). Ndipo Mulungu
Ngodziwa kwambiri Ngwanzeru
zakuya.
171. E inu anthu a Buku!
Musamalumphe malire
Pachipembedzo chanu. Ndipo
musamnenere Mulungu koma
zowona (zokhazokha) Ndithu
Mesiya Yesu mwana Wa Maria,
ndi mtumiki wa Mulungu
(ndiponso ndi munthu
wolengedwa) Ndi liwu lake
lomwe adaliponya kwa Maria
Ndiponso (ali) ndi mzimu
wochokera kwa lye (Mulungu,
monga Mizimu ina yonse
Imachokera kwa lye). Choncho
Khulupirirani Mulungu ndi
atumiki Ake. Musamanene "Utatu
wa Mulungu;" siyani,
(Zikhululupiriro za utatu wa
Mulungu), kutero Ndibwino kwa
inu. Ndithudi, Mulungu ndi
Surat4. An-Nisa' Juzu 6
223
n frjJrt
£ fLwJl 5jJ~J
Mulungu m'modzi (basi).
Ulemerero wake ngotukuka kutali
ndi kukhala Ndi mwana. Nzake
zonse zakumwamba ndi pansi.
Ndipo Mulungu ndiMtetezi
Wokwanira.
172. Mesiya (Mneneri Yesu)
sangaone kunyozeka Kukhala
kapolo wa Mulungu ngakhalenso
Angelo oyandikitsidwa (kwa
Mulungu). Amene angaone
kunyozeka paukapolo wake Kwa
Mulungu nazitukumula, onse
Adzawasonkhanitsa kwa lye
(ndipo Kenako nkuwalonga
kung'anjo ya moto).
173. Koma amene
adamkhulupirira (Yesuyo) Ndi
kuchita zabwino Adzawapatsa
malipiro ao bwinobwino ndi
Kuwaonjezera ndi zabwino zake.
Koma amene Adaona kunyozeka
(pokhala kapolo wa Mulungu)
nadzitukumula,adzaalanga
Ndichilango chowawa; ndipo
sadzapeza bwenzi Ngakhale
mtetezi kupatula Mulungu.
174. E inu anthu! Ndithudi,
Wakudzerani umboni Wochokera
kwa Mbuye Wanu. Ndipo
takuvumbulutsirani Kuunika
koonekera poyera.
175. Tsono amene akhulupilira
Mulungu Ndi kudziphatika kwa
} > »> ft* y,,'s ..sts 9'
&\>,\p\&<£\w$
Surat4. An-Nisa'
Juzu 6
224
t *>»
t *L*Jl 5jJ-*»
lye, Iwo adzawalowetsa ku
Chifundo Chake ndi kuzaufulu
Zake (mtendere) ndikuwatsogolera
kwa lye panjira yoongoka.
176. Akukufunsa (iwe Mneneri,
za malamulo Achuma cha munthu
yemwe wafa osasiya Mwana
kapena kholo). Nena: "Mulungu
Akukulamulani pazayemwe
sadasiye mwana Ndi kholo (kuti)
ngati munthu atamwalira Pomwe
alibe mwana, koma ali ndi mlongo
Wake, choncho (mlongo wakeyo)
alandire Theka (Vi) ya zomwe
wasiya (womwalirayo). Nayenso
angalandire chuma (chamlongo
wake) Ngati (womwalirayo) alibe
mwana. Ngati Iwo ali (alongo)
awiri, ndiye kuti Adzalandira
zigawo ziwiri muzigawo zitatu
C^Aj ) Za zomwe wasiya. Ngati ali
pachibale amuna Ndi akazi, ndiye
kuti mwamuna aliyense alandire
Gawo lolingana ndi la akazi awiri.
Umo Ndi momwe Mulungu
akukufotokozerani (Malamulo
Ake) mwatsatanetsatane kuti
Musasokere. Ndipo Mulungu
Ngodziwa chilichonse
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 6
225 1 »>•
OJjlit OjJ~»
Surat Al-Ma'idah V
C\--'^-. "±:y-
M'dzina la Mulungu waChifundo
Chambiri, waChisoni.
1. "E inu amene
mwakhulupirira! Kwaniritsani
Mapangano onse (omwe ali pakati
panu ndi Anthu anzanu).
Kwalolezedwa kwainu (kudya
Nyama ya) ziweto (monga
ngamira, ng'ombe Ndi mbuzi),
kupatula chomwe mukuuzidwa
(Kuti ncholetsedwa). Koma
nkosaloledwa Kwainu kuchita
ulenje mutalowa M'mapemphero a
Haji, (kapena muli M'nthaka
yopatulika ya ku Makka).
Ndithudi, Mulungu akulamula
chimene wafuna. 1
2. "E inu amene
mwakhulupirira! Musanyozere
Kupatulika kwa zizindikiro za
Mulungu (Kuchiyesa
chosapatulika chomwe Mulungu
Adachichita kukhala chopatulika;
monga Kutuluka m'mapemphero a
Haji usadakwaniritse), Kapena
mm : . #-
Q£ft$»lfc#2l^l,
-^
1 Chisilamu chimalemekeza zinthu zogwirira ntchito ya chipembedzo, monga
ziweto zimene amazitumiza ku Makka ncholinga choti akazizinge kumeneko
monga sadaka yopereka konko. Ndipo anthu okachita mapemphero a Hajiwo,
ziweto amaziveka zizindikiro zosonyeza kuti nziweto zomwe akukazipereka
monga nsembe ku nyumba ya Mulungu mu mzinda wa Makka. Ndipo
nyamazo zimakhala zopatulika. Choncho sibwino kuswa kupatulika kumeneku
pozilanda mwachifwamba ndi kuzipha zisanafike pamalo pake poziphera.
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 6
226 1 *>'
o daJlit ojj^t
kupatulika kwa mwezi wopatulika
(Poyambitsa nkhondo mmenemo),
Kapena (kupatulika kwa nyama
zomwe Zatumizidwa ku Makka
monga) nsembe Kapena (kuchotsa
kupatulika Kwa) makoza (omwe
nyamazo Zimavekedwa monga
chizindikiro chosonyeza Kuti
ndinsembe ya ku Makka), kapena
(Kupatulika kwa) omwe akulinga
kupita Kunyumba yopatulika (ku
Makka), (omwe Akupita
kumeneko) ndi cholinga
chofunafuna Ubwino wa Mbuye
wawo ndi chiyanjo Chake. Ngati
Mutatuluka m'mapemphero Anu a
Haji, mukhoza kuchita ulenje
(ngati Mutafuna); Ndipo
kusakuchititseni kuwada Anthu
chifukwa chakuti adakutsekerezani
kufika Ku Mzikiti wopatulika ( wa
ku Makka) kuti Mulumphe malire.
Pobwezera mtopola umene
adakuchitirani) Koma thandizanani
pazabwino ndikuopa (Mulungu);
musathandizane pamachimo Ndi
pa chidani. Ndipo muopeni
Mulungu. Ndithu Mulungu
Ngwaukali pokhaulitsa.
3. Kwaletsedwa kwainu (kudya)
chakufa chokha, Ndi liwende, ndi
nyama yankhumba, ndi Chomwe
chazingidwa m'dzina osati la
Mulungu, ndi chomwe chafa ndi
kubanika, Ndi chomwe chafa ndi
M
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 6
227 1 *>■»
dJJlil djj^
kumenyedwa, ndi Chimene chafa
pakugwa (Kuchokera paphiri
losongoka) ndi chimene Chafa
polasidwa ndi nyanga
(yachinzake), Ndi chomwe chafa
pakujiwa ndi chilombo (Cha
m'thengo) kupatula chomwe
mwachipeza Chili moyobe,
nkuchizinga. Ndi chimene
Chazingidwa paguwa la mafano;
ndiponso (Nkoletsedwa kwa inu)
kufuna kudziwa zobisika Pochita
maula. Zonsezi ndi uchimo. Lero
amene sadakhulupirire ataya
mtima (Zakugonjetsa)
chipembedzo chanu. Choncho
Musawaope, koma opani Ine. Lero
Ndakukwaniritsirani chipembedzo
chanu ndipo Ndakwaniritsa pa inu
chisomo changa. Ndakusankhirani
Chisilamu Kukhala chipembedzo
chanu. Koma amene Wasimidwa
chifukwa chanjala, popanda
Kupendekera kumachimo, (nkudya
zoletsedwazi, Palibe kanthu).
Ndithu, Mulungu Ngokhululuka
Kwambiri, Ngwachisoni. 1
1 Apa atchulapo zinthu zoletsedwa kuzidya. Zinthuzi ndi izi> (a) Nyama imene
yadzifera yokha. (b) Liwende (uwende). (c) Nyama yankhumba. (d) Nyama
imene aizinga ndi cholinga china, osati ncholinga cha Mulungu monga:-
(1) Nyama imene aizinga chifukwa chotsirika nyumba kuti ziwanda
zisamavutitsemo.
(2) Nyama imene aizinga pofuna kusangalatsa chiwanda cham'nyumba
kapena cham'munda kuti chisangalale. Kapenanso pofuna kusangalatsa
mzimu wa munthu wakufa kuti ngati sazinga nyama ndiye kuti uzivutitsa ana
kapena anthu okhala panyumbapo.
(3) Nyama imene aizinga pofuna kutsirika mudzi, kapena kuti chaka chino
tikapanda kuzinga nyama kubwera matsoka akutiakuti.
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 6
228 1 *j*-»
O OJJlil
h**
4. Akukufiinsa (Asilamu)
chomwe chaloledwa Kwa inu
(kudya). Nena: "Chaloledwa kwa
inu Chilichonse chabwino. Ndi
chimene chagwidwa Ndi nyama
kapena mbalame zomwe
Mwaziphunzitsa kusaka.
Muziphunzitse zimene Mulungu
wakuphunzitsani. Choncho idyani
Chimene zakugwirirani, ndipo
chitchulireni Dzina la Mulungu
pochikhwirizira. Ndipo opani
Mulungu. Ndithudi Mulungu
Ngwachangu pakuwerengera. l
(4) Nyama imene aizinga pofuna kutsirika ukwati kuti ulimbe kapena pofuna
kutsirika yemwe wabwera kuulendo kuti asamlodze;
(5) Nyama imene aizinga ncholinga choti akataye bwino maliro, ndi kuti
mzimu wamalirowo usavutitse anthu pamudzi; Nyama zonse zimene
zazingidwa ndizolinga monga izi tatchulazi, nzoletsedwa kuzidya. Ndipo
kunena koti "Chimene chafa ndikumenyedwa ncholetsedwa koma
pokhapokha mutachipeza chili moyobe nimuchizinga," tanthauzo lake nkuti
nyama imene imadyedwa ngati itafa pazifukwa zina zilizonse, monga
kugundidwa ndi galimoto ndi zina zotero ndipo nyamayo sinaferetu kotero
kuti nkutheka kuizinga, nyama yotero njololedwa kuidya.
1 Mbalame ndi nyama zimene zaloledwa kuzisaka mwaulenje kupyolera
mwambalame kapena mwanyama zinzawo zomwe anaziphunzitsa kusaka,
ndipo mbalamezo kapena nyamazo nkufa chifukwa chakulumidwa ndi mbalame
kapena nyama zosakazo, zikuloledwa kuzidya ngakhale kuti sanaztzinge.
Koma ngati atazipeza zikalipobe ndi moyo, azizinge.
N B! Ndipo Mulungu nyama zomwe akuzilola kuti zizisaka zinzawo nzomwe
zili ndimano akuthwa ndi zikhadabu zakuthwa ndipo zitalizitali. Chimodzimodzi
ngati nyama ndi mbalame zitaphedwa ndi mipaliro kapena mikondo kotero
kuti zaferatu, zikuloledwa kuzidya ngakhale kuti sadazizinge. Koma
akazipeza zili moyobe, azizinge. Koma chida chimene chikupha mopsinja
monga mwala ndi chibonga (chamtunga) kapenanso chida chokhala ndi
moto, monga chipolopolo chamfuti, nyamayo kapena mbalameyo siiloledwa
kudyedwa ndi mazingidwe oterowo. Koma chikapezeka kuti chili ndimoyobe
ndipo nkuchizinga, pamenepo chikhala chololedwa kuchidya. Koma Mazihabi
a Maalik akuti nchololedwanso kuchidya chinthu chimene chafa chifukwa
cholasidwa ndi mwala kapena ndi chipolopolo chamfuti. Ndipo ganizoli
akulitsata ambiri kuphatikizapo a Mazihabi a Shafi. Tsono chimene chili wajibu
pozinga nyama pa Mazihabi a imam Shaafi ndichimodzi basi. Uku nkuchidula
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 6
229 1 *>»
O OJU'lil
Oj^
5. Lero mwaloledwa zonse
zabwino ndi Chakudya cha omwe
adapatsidwa Buku nchololedwa
kwa inu, ndiponso Chakudya
chanu nchololedwa Kwa iwo ndipo
(mukuloledwa kuwakwatira) Akazi
abwino a mwa Asilamu ndi akazi
Abwino a mwa omwe adapatsidwa
ma buku Kale, ngati mwawapatsa
chiwongo Chawo m'njira yomanga
nawo ukwati, Osati mochita
chiwerewere, Osatinso mochita
zibwenzi. Ndipo amene Akane
kukhulupirira, ndiye kuti
Yaonongeka ntchito yake; ndipo
lye tsiku lomaliza adzakhala mwa
oluza. l
chinyamacho mwachangu njira imene imalowera chakudya ndi njira imene
mpweya umalowera. Ndipo zina zotsatira pazimenezi ndisunna, monga.-
(a) kuiyang'anitsa kuchibula (nyamayo)
(b) kunena mawu akuti "Bismillah"
(c) Mpeniwo ukhale wakuthwa
(d) Kuigoneka pamalo posapweteka. Tsono kunena kwakuti "Mkazi
sangazinge nyama ndi kutinso mpeni ukhale ndi chogwirira (chigumbu)," ndi
mawu opanda pake. Msilamu aliyense, mwamuna ndi mkazi akhoza kuzinga
ngati akudziwa.
1 Chakudya chozingidwa sichingakhale chovomerezeka kwa Asilamu
pokhapokha chitazingidwa ndi Asilamu. Izi zili ngati atatsatira malamulo
talongosola aja pozinga, osati kupotokola khosi, kapena kumenya ndimyala
kapena chibonga.
Tsono chakudya chozingidwa nchovomerezeka kwa Msilamu kuchidya
ngakhale chitakonzedwa ndi achikunja (akafiri) monga momwe zilili
m'Mazihabi a Chisunni malinga ngati:-
(a) simudaone kuti athiramo najisi (uve)
(b) Sichili chakudya choletsedwa
Nkovomerezeka kwa mwamuna wa Chisilamu kukwatira:-
(a) Mkazi wa Chiyuda
(b) Mkazi wa Ghikhrisitu ngati makolo awo adali Ayuda kapena Akhrisitu
chisilamu chisanadze.
N.B! Koma awa a Mishoni omwe alowa m'Chikhrisitu posachedwapa
nkosaloledwa kuwakwatira pokhapokha atayamba alowa m'Chisilamu Tsono
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 6
230 1 *>»
O dJJlll
pj^-.
6, "E inu amene
mwakhulupirira! Pamene
Mwaimilira kuti mukaswali,
sambitsani Nkhope zanu, ndi
manja anu mpaka Mmagongono;
ndipo pakani madzi pamitu panu
Ndi kusambitsa mapazi anu mpaka
muakakolo. Ngati muli ndi janaba
dziyeretseni (sambani Thupi
lonse); Ndipo ngati muli odwala
kapena Muli paulendo, kapena
mmodzi Wanu wachokera
kokadzithandiza Kapena
mwakhalira limodzi ndi mkazi
ndiye Simudapeze madzi, chitani
Tayammamu Ndi dothi labwino
ndipo pakani kunkhope Zanu ndi
mmanja mwanu. Mulungu
sakufuna Kukuvutitsani, koma
akufuna kukuyeretsani Ndi
kukwaniritsa chisomo chake painu
Kuti muthokoze .
7. Ndipo kumbukirani chisomo
cha Mulungu Painu ndi pangano
lake lomwe mudapangana Naye,
pamene mudati: "Tamva; ndipo
•f*"T <" \z,< \>* **???
»*/ 99} , 9 s ^*r< r^«»K \* * '
mkazi wa Chisilamu nkosaloledwa kukwatiwa ndi myuda kapena mkhrisitu.
Ndipo apa apitirizanso machitidwe achiwerewere chomangira nyumba ndi
chapatchire. Munthu akafuna kukwatira mkazi atsate mfundo zikudzazi kuti
ukwati wakewo ukhale wovomerezeka pa malamulo a Chisilamu:-
(a) Mkazi alole kukwatiwa ndi mwamunayo.
(b) Myang'aniri wa wamkazi apereke kwa munthu chilolezo choti akwatitsire
mkazi uja, kapena amkwatitse iye mwini pomuuza mkwati kuti "Ndakukwatitsa
uje,mwana wauje".
(c) Mkwati avomereze kuti: "Ndavomera kumkwatira uje, mwana wauje".
(d) Pakhale anthu aamuna oikira umboni osachepera pa awiri. Anthuwo
akhale aulemu wawo pamaso pa anthu.
Siirat 5. Al-Ma'idah Juzu 6
231
n tjJt-i
o dJkjdi djj~*
tamvera." Muopeni Mulunguyu.
Ndithudi Mulungu Ngodziwa
zam'mitima.
8. "E inuamene
mwakhulupirira! Khalani
Olungama (pokwaniritsa choona)
cha Mulungu perekani umboni
mwachilungamo, Ndipo kudana
ndi anthu kusakuchititseni Kuti
musachite chilungamo. Chitani
Chilungamo; kutero
kumakuyandikitsani Ku "taquwa"
(Kuopa Mulungu). Ndipo opani
Mulungu. Ndithudi, Mulungu
Ngodziwa nkhani Zonse za
(zinthu) zomwe muchita.
9. Mulungu walonjeza omwe
akhulupirira Ndi kuchita zabwino
kuti adzapeza chikhululuko Ndi
malipiro aakulu.
10. Ndipo amene
sadakhulupirire, Natsutsa
zizindikiro Zathu, Iwo ndi anthu
akumoto. 1
11. "E! inu amene
mwakhulupirira! Kumbukirani
Mtendere wa Mulungu omwe uli
painu. (Kumbukirani) pamene
anthu ena Adatsimikiza
kukutambasulirani manja awo
©(
1 Mulungu akukumbutsa Asilamu zachifundo chake powachotsera masautso
amene anangotsala pang'ono kuwagwera ndi kuti apitirize kuyamika Mulungu
ndi kuyadzamira kwa lye osati kumizimu ya anthu akufa, zithumwa, nyanga
ndi mitsiriko yamtundu uliwonse.
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 6
232
n ftjA-i
dJJlit
°J>*
(Pofuna kuchita nanu nkhondo)
Koma adawatsekereza Manja awo
kukufikani inu. Choncho Opani
Mulungu. Ndipo kwa Mulungu
Yekha, ayadzamire okhulupirira.
12. Ndipo ndithudi, Mulungu
adamanga pangano Ndi ana a
Israeli, ndipo tidawaikira
Akuluakulu khumi ndi awiri mwa
iwo. Ndipo Mulungu adati:
"Ndithudi Ine ndili pamodzi ndi
Inu ngati mupemphera swala
ndikupereka Chopereka,
ndikukhulupirira atumiki Anga,
Ndi kuwalemekeza ndi
kumkongoza Mulungu Ngongole
yabwino, ndithudi
ndikufafanizirani Zoipa zanu,
ndikudzakulowetsani M'minda
yomwe pansi ndi patsogolo pake
Pakuyenda mitsinje. Koma amene
akane Mwainu pambuyo pa
(chipangano) Ichi, ndithu, wataika
(kuchokera) Kunjira yowongoka".
13. Choncho chifukwa
chakuswa pangano lawo,
Tidawatemberera; ndipo
tidaumitsa mitima Yawo.
Ankasintha mawu (a Mulungu
Omwe adali M'mabuku a Taurat
ndi Injili) kuwachotsa M'malo
mwake ndipo adasiya
Kukwaniritsa gawo lalikulu La
zomwe adakumbutsidwa. Ukhala
©(£)J**J&\
W^'S i9l* \'&< ' * 9 9 9K. * <' '
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 6
233
n tj*r\
O dJjlil Ojj~>
ukuona (Iwe Mtumiki {SAW})
chinyengo mwa ambiri Aiwo,
kupatula ochepa aiwo. Choncho
Akhululukire ndi kuwaleka.
Ndithudi, Mulungu amakonda
ochita zabwino. 1
14. Naonso aja amene akuti:
"Ife ndife Akhrisitu", Tidalandira
pangano lawo koma adasiya Gawo
lalikulu lazomwe
adakumbutsidwa. Tero tidaika
pakati pawo chidani Ndi
kusakondana mpaka tsiku
Lomaliza. Ndipo Mulungu
Adzawawuza zimene adali kuchita. 2
15. " E inu anthu a Buku!
Ndithudi wakufikani Mtumiki
Wathu yemwe Akukufotokozerani
1 Ndime iyi ikupitirizanso kutchula zina mwazoipa za Ayuda. Ndipo zina
mwaizozi ndiko kusintha mawu a M'buku lawo lomwe Mulungu
adawavumbulutsira. Iwo ankachotsamo mawu omwe sadali kuwafuna
naikamo amene ankawafuna.
Zoterezi Akhristu anazichitanso. Ndipo akuchitabe mpaka lero. Mabaibulo
awo omwe akusindikiza nkuwagawa m'maiko athu kuno ku Africa ndi kwina
kulikonse ngati utaona mofatsa lomwe asindikiza posachedwapa upeza
kusiyana pang'ono ndi lomwe adasindikiza m'mbuyomu. (a) Mwina
akuchotsa zimene zidalimo (b) Kapena akuikamo zomwe mudalibe (c) Mwina
matanthauzo achiganizo amawasinthiratu kusiyana ndi momwe zidalili M'buku
lomwe adasindikiza kale. Zonsezi zikusonyeza kuti amenewa ndiwo
machitidwe awo pofuna kukopa anthu ambiri kuchipembedzo chawo. Akaona
kuti ichi chikopa anthu ambiri, amachiikamo nanena kuti ndi mawu a Mulungu.
Ndipo akaona kuti malamulo awa apirikitsa anthu amawachotsa kapena
kuwachepetsa mphamvu yake. Umo ndimomwe alili machitidwe awo.
2 Ndime iyi ikusonyeza kupatukana komwe kuli pakati pawo kotero kuti
mpingo wina umayesa Unzake monga wakunja. Monga mpingo wa Roman
Catholic umaiona mipingo ina monga ya Protestant, Orthodox ndi yambiri
ngati mipingo ya chikunja. Zonsezi nchifukwa cha kusatsatira zophunzitsa
zenizeni za Chikhrisitu.
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 6
234
^ pjir\
O dJJlll «jJ-»
poyera Zambiri zomwe munkabisa
za M'buku. Koma akusiya zambiri
(posazilongosola).Ndithudi
kwakudzerani kuunika Kochokera
kwa Mulungu ndi Buku Lomwe
likufotokoza mwatchutchutchu
(Chinthu chilichonse).
16. Ndibukulo Mulungu
akuwatsogolera Kunjira
zamtendere amene akutsata
Chiyanjano chake ndikuwatulutsa
Mu m'dima ndi kuwaika
M'kuunika mwa lamulo Lake, ndi
kuwatsogolera Kunjira yoongoka.
17. Ndithudi, amukana
(Mulungu) amene Akunena kuti
Mulungu ndiye Mesiya Mwana wa
Maria. Nena: "Ndani Angathe
kuletsa chilichonse kwa Mulungu
ngati lye akadafuna kuononga
Mesiya mwana wa Mariayo ndi
mayi Wakeyo, ndi onse omwe ali
m'dziko Lapansi? Ndipo ufumu
wakumwamba Ndi pansi ndi
zapakati pake ngwa Mulungu. lye
amalenga chimene wafuna. Ndipo
Mulungu Ngokhoza chilichonse". 1
>h\ ti s \ ten"* ? " hJ'
1 Mndime iyi atchula zoyankhula zawo zamachimo zoti Isa (Yesu) ndi mwana
wa Mulungu, kapena ndi Mulungu amene, kapena ndi mmodzi mmilungu itatu.
Ndipo akunenetsa za kufooka kwa mneneri Yesu pamaso pa Mulungu monga
kulili kufookanso kwazolengedwa zina.
Ndimeyi ikunenetsanso kuti Mulungu monga amalenga mkalengedwe kamene
lye wafuna, mchosadabwitsa kwa lye kulenga Yesu popanda tate. Ndipo
nchosadabwitsanso kwa lye kulenga Adamu popanda tate ndi mayi. Nanga
nchotani kuti Akhrisitu azimuyesa Mneneri Yesu kuti ndi mwana wa Mulungu
kamba koti alibe tate? Bwanji nanga Adamu naye sakumuyesa mwana wa
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 6
235
n *>■»
o dJJlil djj^
18. Ndipo Ayuda ndi Akhrisitu
akunena: "Ife ndife ana a Mulungu
ndiponso Okondeka ake". Nena:
(Iwe Mtumiki) "Nchifukwa ninji
Mulungu amakukhaulitsani Kamba
kamachimo anu? Koma inu ndinu
anthu chabe mwa omwe
Adawalenga. Amamkhululukira
amene Wamfuna (akalapa); ndipo
amamulanga amene Wamfuna
(akapanda kulapa). Ufumu
Wakumwamba ndi pansi ndi
zapakati pake Ngwa Mulungu.
Ndipo Kwa lye nkobwerera."
19. E inu anthu a Buku!
Ndithudi, Wakudzerani Mtumiki
Wathu Yemwe akukufotokozerani
inu, Panthawi yopanda aneneri,
Kuti musadzanene kuti: "Sadadze
kwa ife wonena Nkhani zabwino
ndiwochenjeza." Choncho
wakudzeranidi wonena Nkhani
zabwino ndi wochenjeza. Ndipo
Mulungu Ngokhoza chilichonse.
20. (Ndipo kumbukirani)
pamene Musa adauza Anthu ake:
"Inu anthu anga. Kumbukirani
Mtendere wa Mulungu umene uli
painu, Adawachita ena mwa inu
kukhala aneneri; Ndipo
adakuchitani kukhala mafumu
(Pambuyo poti mudali onyozeka
M'dziko la Iguputo m'manja mwa
•£•
©
Mulungu poti nayenso alibe tate ndi mayi? Ndibwino kutsata choonadi
ngakhale choonadicho chikuchokera kwa mdani. Choonadi ndi choonadi.
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 6 236 1 *>»
o djjdi djj~>
Farawo). Ndipo wakupatsani
zomwe Sadampatsepo aliyense
Mwazolengedwa (mwa anthu
anzanu)." {
21. " Inu anthu anga. Lowani
M'dziko loyeretsedwalo Limene
Mulungu adakulemberani, Ndipo
musabwerere m'mbuyo kuti
Mungasanduke otaika."
22. (Iwo) adati: "Iwe Musa,
ndithudi Mmenemo muli anthu
amphamvu. Ife sitikalowamo
kufikira Atatulukamo okha. Ngati
Atatulukamo, pamenepo Ndipo
tikalowa."
23. Anthu awiri mwa amene
ankaopa Mulungu, omwe awiriwo
Mulungu Adawapatsa chisomo,
adati (Kwa anzawo): "Alowereni
pachipata (Chadzikolo). Ngati
mukalowamo Ndithudi, inu
mukapambana.Ndipo kwa
Mulungu Yekha yadzamirani ngati
inu mulidi Okhulupirira
(Mulungu)."
24. (Iwo) adati: "Iwe Musa, ife
Sitikalowamo mpang'ono pom we,
Pomwe iwo ali momwemo.
Choncho pita iwe ndi Mbuye
* > \ \99\^ 9 ^
1 Mndime iyi akukumbutsa Ayuda chisomo chachikulu chomwe Mulungu
adawadalitsa nacho. Kuyamika zomwe Mulungu watichitira nkofunika kwabasi.
Tisakhale ngati anzathu awa amene Mulungu adawadalitsa ndimadalitso
osiyanasiyana koma osamthokoza, ndiponso osamkonda ndi chikondi
chochokera pansi pamtima.
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 6
237
1 *>t
e dJJLii djj**>
Wako, ndi kumenyana nawo; Ife
tikhala pompano."
25. (Musa) adati: "E Mbuye
wanga! Ndithudi, ine ndilibe
nyonga Koma paine ndekha ndi Pa
mbale wanga. Choncho
Tisiyanitseni ndi anthu Awa
opandukira chilamulo."
26. Mulungu adati: "Choncho
laletsedwa Dzikolo kwa iwo
kulilowa kwa zaka Makumi anayi.
Akhala akuyendayenda Padziko.
Tero, usawadandaulire Anthu
opandukira chilamulo."
27. Ndipo awerengere nkhani
mwachoonadi ya ana Awiri a
Adamu, pamene adapereka
nsembe. Ndipo idalandiridwa ya
mmodzi wawo. Koma Yawinayo
siidalandiridwe. (Amene nsembe
Yake siidalandiridwe) adati (kwa
mnzake): "Ndithudi ndikupha."
Mnzakeyo adati; "Ndithudi,
Mulungu amalandira nsembe ya
Amene akuopa (Mulungu). 1
<"* \\\ 9 <A\ "" \'< 9 ' W*\<
lyi ndinkhani yoyamba ya munthu wopha mnzake. Ndipo amene
adaphedwayu ndiye munthu woyamba kulawa imfa. Wopha mnzakeyo
ataona kuti mnzake wafadi, iye adangoti kakasi, kusowa chochita naye. Tero
adangomsenza kumsana nkumangozungilirazungulira naye, kuopa kubwera
naye kunyumba kuti anzake angamdziwe kuti ndiye wamupha. Makolo awo
adali Adamu ndi Mayi Hava. Mwamwayi, khwangwala adatulukira nayamba
kumenyana ndimnzake mpaka kumupha. Kenako namkwirira m'nthaka.
Tsono naye uja wopha mnzake adatsanzira zomwe khwangwala adachita.
Nakumba dzenje nkukwirira mnzakeyo. N.B! Munthu ncholengedwa
chomalizira kudza padziko. Zidamtsogolera zolengedwa zonse ndi zaka
miyandamiyanda.
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 6
238
% *>»
d dJjlli Ojj-*»
28. Ngati utambasula dzanja
lako Paine kuti undiphe, ine
sinditambasula Dzanja langa paiwe
kuti ndikuphe. Ndithudi, ine
ndikuopa Mulungu Mbuye
wazolengedwa.
29. "Ine ndikufuna kuti usenze
machimo Anga pamodzi ndi
machimo ako.Choncho ukakhale
m'gulu la anthu Akumoto. Ndipo
iyo ndiyo Mphoto ya anthu ochita
zoipa".
30. Choncho adakokeka ndi
mtima wake Kupha mbale wake,
ndipo adamuphadi. Tero adali
wotaika.
31. Pamenepo Mulungu
adatumiza khwangwala Yemwe
amafukula pansi kuti amusonyeze
Mmene angakwiririre mtembo wa
m'bale wake. (Wopha mnzake)
adati: "Kalangaine! Ndalephera
kuti ndifanane ndi khwangwala
Uyu, kuti ndikwirire mtembo wa
m'bale wanga". Choncho adali
mmodzi wodzinena.
32. Pachifukwa chazimenezo,
tidawalamula Ana a Israeli kuti
amene wapha munthu Popanda
iye (wophedwayo) kupha munthu,
Kapena popanda kuchita
chisokonezo Padziko, ali ngati
wapha anthu onse.Ndipo Amene
wamuleka munthu ali ndimoyo,
<a'J-' JA VJ>tJ'U\ *"tf*
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 6
239
1 *j*-»
O flJU'lil
5 J>-*
Ali ngati awapatsa moyo anthu
onse. Ndithudi, atumiki athu
adawadzera ndi Zisonyezo
zoonekera. Koma ndithu ambiri
Aiwo, pambuyo pazimenezo,
adapitirizabe Kuononga padziko.
33. Choncho, mphoto ya amene
akulimbana ndi Mulungu ndi
Mtumiki Wake (pochita zomwe
Waletsa) ndi kudzetsa
chionongeko padziko, Aphedwe
kapena apachikidwe pamtanda,
Kapena adulidwe manja awo ndi
miyendo Yawo mosemphanitsa
dzanja lakumanja ndi Phazi
lakumanzere, ndipo dzanja
lakumanzere Ndi phazi
lakumanja); kapena apirikitsidwe
Mdzikomo. Uku ndikuyaluka
kwawo padziko Lapansi. Ndipo
iwo pa tsiku lomaliza Adzalandira
chilango chachikulu; 1
34. Kupatula amene alapa
Musanawagwire. Ndipo dziwani
'J&&m£0%
1 Apa atchula chilango chowapatsa anthu owononga, amene amafwamba
anthu m'njira zawo. Anthu otere alandire zilango izi:-
(a) Ngati akungopha oyenda m'njiramo popanda kuwatengera chuma chawo
akawapha, iwo akagwidwa chiweruzo chawo nkuphedwa nawonso.
(b) Ngati akupha ndi kulanda chuma, atagwidwa chiweruzo chawo
nkuphedwa. Ndipo akaphedwa choncho awapachike pamtanda kwamasiku
atatu asanawaike m'manda. Kapena choyamba awaweruze kuti apachikidwe
ali moyo. Ndipo akatsala pang'ono kufa, awatsitse ndi kuwamaliza.
(c) Ngati amangolanda chuma chokha popanda kupha, akagwidwa chiweruzo
chawo onse nkuti adulidwe dzanja lakudzanjadzanja aliyense ndi phazi
lakumanzere. Kapena dzanja lamanzere ndi phazi ladzanjadzanja
(d) Ngati saapha ndiponso salanda chuma, koma amangovutitsa anthu ndi
kuwaopseza, chiweruzo chawo nkuwachotsa m'dzikomo kuwapititsa kwina
nkuwapatsa ukaidi kumeneko, kapena kuwanjata m'dziko momwemo.
Siirat 5. AI-Ma'idah Juzu 6
240 1 ^>
O dJU'til djj~*»
kuti Mulungu Ngokhululuka
Kwambiri, Ngwachisoni.
35. E inu amene
mwakhulupirira! Muopeni
Mulungu ndipo funafunani Njira
zokufikitsani kwa lye. Menyani
nkhondo pa njira yake Kuti
mupambane.
36. Ndithudi, aja amene
sadakhulupirire, Akadakhala ndi
zonse zam'dziko Ndi zina zonga
izo kuti azipereke Monga dipo
kuti apulumuke kuchilango Cha
tsiku lachimaliziro (Kiyama)
Sizikadavomerezedwa kwa iwo.
Ndipo iwo adzapeza chilango
Chopweteka.
37. Adzafuna (mwanjira
iliyonse) Kuti atuluke kumoto,
koma Sadzatulukamo. Ndipo
Adzakhala ndi chilango
chamuyaya.
38. Ndipo wakuba wamwamuna
ndi Wakuba wamkazi, aduleni
manja A wo; kukhala mphoto Ya
zomwe achita. (Ichi) ndi Chilango
chochokera kwa Mulungu;
Mulungu; Ngwanyonga Zoposa,
Ngwanzeru zakuya.
39. Koma amene walapa
pambuyo Pakuchita kwake zoipa,
nkuchita Zabwino, Mulungu
Alandira kulapa kwake. Ndithudi,
£1
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 6
241
1 *jk-\
o oju'di ijj**
Mulungu Ngokhululuka Kwabasi
Ngwachisoni. 1
40. Kodi sukudziwa kuti
Mulungu Ngwake ufumu
wakumwamba Ndi pansi?
Amamulanga yemwe Wamfuna
(akalakwa), ndipo
Amamukhululukira amene
wamfuna (Akalapa). Ndipo
Mulungu Ngokhoza chilichonse.
41. E iwe Mtumiki!
Asakudandaulitse amene Akuchita
changu kukana Mulungu mwa
omwe Akunena ndi pakamwa
pawo chabe: "Takhulupirira",
pomwe mitima yawo
Siikukhulupirira. Namonso mwa
Ayuda, alipo Amene amadza
kudzamvera zimene ukunena Kuti
akanene bodza. Amene akudza
Kudzakumvera chifukwa cha
anthu ena amene Sadadze kwa iwe
(omwe ndi akuluakulu awo),
Amasintha mawu (a M'buku La
Taurat) m'malo Mwake, omwenso
amanena, (Kuuza otsatira awo
kuti): "Ngati mukapatsidwe (Ndi
Muhammad {SAW}) izi
(takuuzanizi), Kalandireni, koma
ngati musakapatsidwe Zimenezi
kachenjereni." Ndipo munthu
<&£
1 Taona chifundo cha Mulungu! lye akulonjeza wochimwa kuti ngati asiya
machimo ake amlandira. Tero munthu asadzione kuti waonongeka kotero kuti
Mulungu sangamlandire. lyayi! Abwerere ndi mtima wake wonse kwa
Mulungu ndipo Mulungu amlandira.
Surat 5. A I- Ma' id ah Juzu 6
242
■\ *>»
O dJjdt QjJ~*
yemwe Mulungu akufuna kuti
amuyese mayeso sungathe
Kumpezera chilichonse kwa
Mulungu. Iwowo Ndiomwe
Mulungu sadafune kuyeretsa
Mitima yawo. Apeza kuyaluka
padziko Lapansi. Ndipo tsiku
lomaliza adzapeza Chilango
chachikulu.
42. Okonda kumvetsera
zabodza; osaopa Pakudya (zinthu)
zoletsedwa (zaharamu). Choncho
akakudzera aweruze pakati Pawo,
kapena uwapatukire. Ndipo Ngati
uwapatukira, palibe chomwe
Angakuvutitse nacho. Ngati
uweruza Pakati pawo weruza
mwachilungamo. Ndithudi,
Mulungu amakonda olungama.
43. Kodi angakuyese muweruzi
Chotani pomwe iwo Ali nayo
Taurat momwe Muli chiweruzo
cha Mulungu pambuyo
Powaweruza akutembenuka
(Monyoza)! Ndipo iwo sali
okhulupilira.
44. Ndithudi, tidaivumbulutsa
Taurat yokhala ndi chiongoko Ndi
kuunika; aneneri (a Mulungu)
Omwe adagonjera Mulungu, Adali
kulamulira nayo Ayuda, Ndiponso
Arabbaniyuna Ndi (aphunzitsi
amalamulo) Ahabaru (Ansembe)
omwe Adapemphedwa kusunga
Buku la Mulungu ndipo iwo adali
Will, 9' f 9 "4'''''*%. \ , 9S}
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 6
243 1 *>»
O OJU'lil
•-)>*•
mboni pa ilo Choncho (Inu
Asilamu) musaope anthu, Koma
opani Ine. Ndipo musasinthanitse
Aya (ndime) zanga ndi (zinthu za)
Mtengo wochepa. Ndipo amene
Sakuweruza ndi chimene Mulungu
wavumbulutsa, iwowo ndiwo
Osakhulupirira (okana Mulungu).
45. Ndipo m'menemo (M'buku
la Taurat) Tidawalamula kuti:
"Munthu aphedwe Chifukwa
chopha mnzake, ndi kuti diso Kwa
diso, mphuno kwa mphuno; Khutu
kwa khutu; dzino kwa dzino,
Ndiponso kubwezerana mabala".
Koma Amene wakhululuka ndiye
kuti dipo Likhala kwaiye. Ndipo
amene saweruza Ndi chimene
Mulungu wavumbulutsa Iwowo
ndiwo anthu ochita zoipa.
46. Ndipo tidatsatiza pamapazi
a Aneneriwo, Isa (Yesu) mwana
wa Maria Kudzatsimikizira zomwe
zidali Patsogolo pake M'buku la
Taurat. Ndipo tidampatsa Injili
Yomwe m'kati mwake muli
chiongoko Ndi kuunika;
Ndikutsimikizira zomwe Zidali
patsogolo pake za M'buku la
Taurat. Ndipo ndi chiongoko Ndi
ulaliki wabwino kwa oopa
(Mulungu).
47. Anthu Abuku la Injili
alamulire Potsatira zimene
Mulungu Adavumbulutsa
Surat 5. AI-Ma'idah Juzu 6
244
n *>»
O dJjlll
djj^
mmenemo. Ndipo amene asiya
kulamulira ndi Zomwe Mulungu
wavumbulutsa Iwo ndiwo
opandukira Malamulo a (Mulungu).
48, Ndipo takuvumbulutsira
Buku ndi choonadi, Lomwe
likuikira umboni Mabuku omwe
adalipo Patsogolo pake, ndi
kuwateteza, (monga Ponena kuti:
"Lamulo ili ndiloona; ili iyayi").
Choncho weruza pakati pawo
ndizomwe Mulungu
wavumbulutsa, ndipo usatsate
zofuna Zawo kusiya choona
chomwe chakufika. Ndipo
M'badwo uliwonse mwainu
tidaupangira shariya (Malamulo)
ake ndi njira yake. Mulungu
akadafuna, akadakuikani kukhala
Mpingo umodzi (wotsata
chilamulo chofanana). Koma
akufuna kukuyesani pazomwe
Wakupatsani. Choncho pikisanani
pazinthu Zabwino. Inu nonse
kobwerera kwanu nkwa Mulungu.
Naye adzakuuzani (nonsenu) mu
Zomwe mudali kusiyana;
49. Weruza pakati pawo
ndichimene Mulungu
wavumbulutsa, ndipo Usatsate
zofuna zawo, koma Chenjera nawo
kuti angakusokoneze Posiya zina
mwazimene Mulungu
Wavumbulutsa kwaiwe. Ndipo
Ngati anyozera dziwa kuti
®(^j3uJulpA
up*.
ife&to&jw
%&$J&\&M&^
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 6
245
■wjA-1
o dJJdi
djj-
Mulungu Afuna kuwapatsa
chilango cha ena Mwa machimo
awo. Ndithudi, Anthu ambiri
ngopandukira (Malamulo a
Mulungu).
50. Kodi iwo akufuna
chiweruzo cha nthawi yaumbuli
(chamasiku aumbuli, Chisilamu
Chisanadze)? Kodi ndani ali
wabwino Polamula koposa
Mulungu? (Izi nzodziwika) kwa
anthu Otsimikiza (kuti Mulungu
alipo).
51. "E inuamene
mwakhulupirira! Ayuda ndi
akhrisitu musawapale Ubwenzi
(nkumawauza chinsinsi chanu).
Iwo pakati pawo ndi abwenzi ndi
atetezi Kwa wina ndi mnzake.
Amene awapale Ubwenzi mwa
inu, ndiye kuti iye ndi M'modzi
wa iwo. Ndithudi, Mulungu
Satsogolera anthu ochita zoipa.
52. Uwaona omwe m'mitima
mwawo muli matenda (A
chinyengo) akuthamangira kwa
iwo (Ayuda) Uku akuti: "Tikuopa
lingatigwere tsoka (Ngati
Asilamuwa atagwa m'tsoka)".
Koma Posachedwapa Mulungu
abweretsa lamulo Logonjetsa
(midzi), kapena chinthu china
Chochokera kwa Iye (monga
kuwaulula Achinyengo zomwe
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 6 246 t *}*■*
dJJlil djj^j
akubisa m'mitima mwawo).
Choncho adzasanduka odzinena
Chifukwa cha zomwe adabisa
m'mitima mwawo.
53. Ndipo amene adakhulupirira
nayamba Kunena (Chitaululika
chinyengo chawocho): "Kodi awa
siomwe adali kulumbirira Dzina la
Mulungu m'kulumbirira kwawo
Kwamphamvu kuti iwo ali
Pamodzi Ndi inu?" Zochita zawo
zaonongeka. Tero akhala otaika.
54. "E inu amene
mwakhulupirira! Amene Mwa inu
asiye chipembezo chake, Ndiye
kuti posachedwapa Mulungu
Adzabweretsa anthu omwe
Awakonda, nawonso amkonda;
Odzichepetsa kwa Asilamu
anzawo; Amphamvu kwa
osakhulupirira; Omenyera
nkhondo chipembezo Cha
Mulungu, saopa kudzudzula Kwa
odzudzula. Umenewu ndi Ubwino
wa Mulungu; amaupereka Kwa
amene wamfuna. Ndipo Mulungu
ndi Mataya; Ngodziwa kwambiri.
55. Ndithu, Mtetezi wanu ndi
Mulungu Ndi Mtumiki wake ndi
omwe Akhulupirira omwe
akupemphera Swala ndi kupereka
chopereka Uku ali odzichepetsa.
56. Ndipo amene achite
Mulungu Ndi Mtumiki Wake, ndi
®?> \\ 9 l"'y.» 9 A"A
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 6
247
n *>i
O AJU'iLl
dj^-
omwe Akhulupirira kukhala atetezi
ake, (Ndithu, iwo ndi achipani cha
Mulungu). Ndithu chipani cha
Mulungu ndicho Chopambana.
57. E inu amene
mwakhulupirira! Musapalane
nawo ubwenzi omwe
Akuchichitira chipongwe ndi
masewera Chipembedzo chanu
mwa omwe Apatsidwa mabuku
patsogolo panu, Ndiponso mwa
osakhulupirira, Ndipo opani
Mulungu Ngati inu mulidi
okhulupirira.
58. Mukaitanira kokapemphera
Swala (Mukachita azana)
Akuichitira chipongwe ndi
masewera; Zimenezo nchifukwa
chakuti iwo Ndi anthu opanda
nzeru.
59. Nena: "E inu anthu a Buku!
Kodi Mukuona cholakwika kwa ife
kaamba Kakuti takhulupirira
Mulungu ndi Zomwe
zavumbulutsidwa kwa ife Ndi
zomwenso zidavumbulutsidwa
Kale? Ndithudi, ambiri mwa inu
ndi Opandukira chilamulo cha
Mulungu."
60. Nena: "Kodi ndikuuzeni za
uja amene Ali ndimalipiro oipa
kwa Mulungu Kuposa izi?
Ndiomwe Mulungu
Wawatemberera ndi kuwakwiira
<8>
(£$£kfr$*@i
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 6
248 1 *>»
O oJb'dt djj^
Ndi kuwasandutsa ena kukhala
Anyani ndi nkhumba, ndi
opembeza Satana. Awo ndiwo
okhala Ndi malo oipa, ndiponso
osokera Njira yowongoka."
61. Ndipo (achinyengo)
akakudzerani, Akunena:
"Takhulupirira", pamene Alowa
kwa inu ali osakhulupirira Ndipo
atulukanso ali Osakhulupirira.
Koma Mulungu Ngodziwa
kwambiri zomwe Akhala akubisa.
62. Uwaona ambiri aiwo
akuthamangira Machimo ndi
mtopola ndi kudya Zoletsedwa.
Ndithudi, Zimene akhala
akuchitazo Ndizoipa kwambiri.
63. Bwanji odziwa zamalamulo
ndi Akuluakulu achipembedzo
sadawaletse Zoyankhula zauchimo
ndi kudya Kwawo zinthu
zoletsedwa? Ndithudi, zomwe
akhala Akuchitazo ndi zoipa.
64. Ndipo Ayuda adati: "Dzanja
la Mulungu Lafumbatika.
(sitikupeza chuma ngati kale).
(Koma sichoncho); manja awo
ndiwo afumbatika (Posachita
zabwino ndi kuchenjerera anthu).
Ndipo atembereredwa chifukwa
chazomwe anena. Koma manja
Ake (Mulungu) Ngotambasuka.
Amapatsa mmene wafunira.
Ndithudi, zimene
X.'
#2
Surat5. Al-Ma'idah Juzu 6
249
1 fr>H
o dju'di Sjj^
Zavumbulutsidwa kwa iwe
kuchokera kwa Mbuye wako,
ziwaonjezera ambiri aiwo (Ayuda)
Kulumpha malire ndi
kusakhulupilira. Ndipo Taika
chidani ndi kusakondana pakati
Pawo mpaka tsiku lachimariziro.
Nthawi Iliyonse akayatsa moto
wankhondo, Mulungu
amauzimitsa. Ndipo amayetsetsa
Kudzetsa chisokonezo padziko,
(Koma Mulungu sawathandiza).
Ndipo Mulungu sakonda
owononga.
65. Ndipo kukadakhala kuti awa
Anthu a Buku adakhulupirira Ndi
kumuopa Mulungu,
Tikadawafafanizira zolakwa Zawo,
ndi kuwalowetsa M'minda
yamtendere.
66. Akadakhala kuti iwo
adaigwiritsa ntchito Taurat ndi
Injili, ndi zomwe
zidavumbulutsidwa Kwa iwo
kuchokera kwa Mbuye wawo
(monga Qurani), ndithudi
akanadya zakumwamba ndi
Zapansi pamyendo yawo. Mwa
iwo alipo Amene akutsatira njira
yabwino. Komanso Ambiri mwa
iwo akuchita zoipa zedi.
67. E iwe Mtumiki! fikitsa
(kwa anthu) Zomwe
zavumbulutsidwa kwa iwe
Kuchokera kwa Mbuye wako.
*<&M£W\ffi3
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 6
250 1 *j*-»
O dJjlil 5jj~j
Ngati suchita, ndiye kuti
sudafikitse Uthenga wake. Ndipo
Mulungu akuteteza Kwa anthu;
(Usaope aliyense). Ndithudi,
Mulungu Satsogolera anthu
osakhulupirira.
68. Nena: "E inu anthu a
Buku! Simuli kanthu
(Pachipembedzo chanu) mpaka
muimirire (Kutsatira malamulo) a
Taurat ndi Injili Ndi zomwe
zavumbulutsidwa kwa inu
Kuchokera kwa Mbuye wanu,
ziwaonjezera Kulakwa ndi
kusakhulupirira ambiri a iwo.
Zomwe zavumbulutsidwa kwa iwe
Kuchokera kwa Mbuye wako
Choncho usadandaulire Anthu
osakhulupirira.
69. Ndithudi, amene
akhulupirira ndi Amene ali
m'chipembedzo cha Chiyuda, ndi
Asabii, ndi Akhrisitu, - amene
akhulupirire Mulungu ndi tsiku
lomaliza, (monga Momwe
akulangizira Mtumiki
Muhammad{SAW}) ndipo nachita
Zabwino, - palibe mantha kwa iwo
Ndiponso sadzadandaula.
70. Ndithudi, tidalandira
pangano Kwa ana a Israeli (kuti
adzamvera Mulungu) ndipo
tidawatumizira aneneri. Nthawi
iliyonse akawadzera mtumiki Ndi
chomwe mitima yawo siinkafuna,
®i
®&£&
Surat 5. AI-Ma'idah Juzu 6
251
n pjtr\
dJJlil djj_-
Adawatsutsa ena (mwa
atumikiwo), Ndipo ena
ankawapha kumene.
71. Ndipo ankaganiza kuti
sipapezeka chilango; Tero adali
akhungu ndi agonthi. Kenako
Mulungu adawalandira Kulapa
kwawo (pamene Adalapa).
Komabe ambiri a iwo adali
Akhungu, ndi ogontha. Ndipo
Mulungu Akuona zimene akuchita.
72. Ndithudi am'kana Mulungu
amene anena kuti, "Mulungu ndiye
Yesu mwana wa Maria", Pomwe
Mesiya adati: "Inu ana a Israeli
Pembedzani Mulungu Yemwe ndi
Mbuye Wanga ndiponso Mbuye
wanu". Ndithudi, amene aphatikize
Mulungu ndi Chinthu china,
ndithudi Mulungu waletsa kwa iye
kukalowa kuMunda Wamtendere,
ndipo malo ake ndi kumoto. Ndipo
anthu ochita zoipa Sadzakhala ndi
athandizi.
73. Ndithudi, am'kana Mulungu
amene Amanena kuti " Ndithu
Mulungu ndi mmodzi Mwa
(milungu) itatu", pomwe palibe
Mulungu wina koma Mulungu
Mmodzi yekha. Ngati sasiya
zomwe Akunenazo, ndithudi,
mwa iwo amene Sadakhulupirire
chiwakhudza Chilango
chopweteka
tf*i*4"i^"?V*. "&rt\(*>
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 6
252
1 *jA-i
OOJlil
Oj^
74. Kodi salapa kwa Mulungu
Ndi kumpempha chikhululuko?
Komatu Mulungu Ngokhululuka
Kwabasi, Ngwachisoni.
75. Mesiya mwana wa Maria
sali chilichonse Koma ndi Mtumiki
wa Mulungu chabe. Ndithudi,
atumiki ambiri adapita Kale
patsogolo pake. Nayenso mayi
wake ndi mkazi Wachoonadi, onse
awiri adali Kudya chakudya,
(ndipo chotsatira chake Amapita
kokadzithandiza. Nanga ndi
milungu yotani yopita
Kukadzithandiza?) Taona momwe
Tikufotokozera kwa iwo
zizindikiro. Taonanso mmene
akutembenuziridwa (Kusiya
choonadi).
76. Nena: "Kodi
mukupembedza Chimene
sichingakupatseni Vuto ngakhale
chabwino, Kusiya Mulungu?
Pomwe Mulungu ndiye
Wakum va; Wodzi wa. "
77. Nena: "E inu anthu a Buku!
Musapyole malire pachipembedzo
Chanu popanda choonadi Ndipo
musatsatire zofuna Za anthu omwe
adasokera kale, Nawasokeretsanso
ambiri, Ndi kusokera kunjira
Yowongoka (yolungama)".
78. Adatembereredwa amene
Sadakhulupirire mwa Ana a Israeli
m'^jM&$S\
.?.*?*. ft**
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 6
253
*>'
oJU'lll
°J>*
kupyolera M'lirime la Daudi Ndi
Yesu mwana wa Maria. Zimenezo
nchifukwa Chakuti adanyoza
ndipo Adali opyola malire.
79. Sadali kuletsana choipa
Chomwe adali kuchichita. Taona
kuipitsitsa zomwe Adali kuchita.
80. Uwaona ambiri aiwo
akupalana ubwenzi ndi Omwe
sadakhulupirire Mulungu,
(opembedza Mafano ndi cholinga
chomenya nkhondo Chipembedzo
cha Chisilamu). Nzoipa Kwambiri
zomwe adadzitsogozera okha. Tero
Mulungu adawakwiira ndipo
M'masautso adzakhalamo muyaya.
81. Ndipo akadamkhulupirira
Mulungu (Moyenera) ndi
mneneriyo (Muhammad {SAW})
ndi zomwe Zidavumbulutsidwa
kwa iye Sakadawachita abwenzi.
Koma ambiri a iwo Ngopandukira
chilamulo cha Mulungu.
82. Ndithudi, uwapeza amene
ali adani Kwenikweni kwa anthu
omwe ali Asilamu ndi Ayuda
komanso Amushirikina
(opembedza mafano). Ndipo
uwapeza oyandikira ubwenzi Ndi
Asilamu ndi awo akunena kuti:
"Ife ndi Akhrisitu." Zimenezo
N'chifukwa chakuti mwa iwo alipo
Ophunzira ndi oopa Mulungu, Ndi
chifukwanso chakuti iwo
(Akhirisitu) sadzitukumula.
'9.4* %<>'<» 99"i< ' ' '<,
Surat 5. AI-Ma'idah Juzu 7
254 V *>i
o Sjtfiii
hy*
83. Ndipo akamva zomwe
zavumbulutsidwa Kwa Mtumiki,
uona maso awo akugwetsa Misozi
chifukwa cha choonadi chomwe
Achizindikira. Akunena: "Mbuye
wathu! Takhulupirira; choncho
tilembeni Pamodzi ndi oikira
umboni (choonadi)."
84. (Atadzudzulidwa polowa
m'Chisilamu Iwo adati):
"Chifukwa ninji Tisamkhulupirire
Mulungu ndi Choonadi chatifika,
pomwe Tikuyembekezera Mbuye
wathu Kukatilowetsa (kumunda
wamtendere) Pamodzi ndi anthu
abwino?"
85. Choncho Mulungu
Adzawalipira, pazomwe Adanena,
minda yomwe Pansi ndi patsogolo
pake Mitsinje ikuyenda.
M'menemo Adzakhala muyaya.
Imeneyo ndiyo mphoto Ya ochita
zabwino.
86. Ndipo amene
sadakhulipirire, Nkutsutsa
zizindikiro Zathu, iwowo ndiwo
Anthu akumoto.
87. E inu amene
mwakhulupirira! Musazichite
zabwino zomwe Mulungu
wakulolezani kukhala Zoletsedwa.
Ndipo musalumphe Malire,
ndithudi Mulungu Sakonda anthu
olumpha malire.
®r.
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 7
255 V ,>»
OJU'lil
°J>-
88. Idyani zabwino zomwe
Mulungu Wakupatsani zomwe zili
zololedwa. Ndipo opani Mulungu
yemwe inu Mukumkhulupirira.
89. Mulungu sangakulangeni
chifukwa Chakulumbira kwanu
kopanda pake. Koma akulangani
kamba ka Malumbiro omwe
mwalumbira Motsimikiza.
Choncho dipo lake Ndikuwadyetsa
osauka khumi ndi Chakudya cha
mlingo wapakatikati Chomwe
mumawadyetsa anthu Anu; kapena
kuwaveka, kapena Kumpatsa ufulu
kapolo. Koma Amene sangapeze
zimenezo, asale Masiku atatu. Hi
ndi dipo Lakulumbira kwanu
pamene Mukulumbira. Ndipo
sungani Malumbilo anu, (musaswe
chomwe Mudalumbirira). Motero
ndi Momwe Mulungu
akukufotokozerani Zizindikiro
Zake kuti muthokoze.
90. E inu amene
mwakhulupirira! Ndithudi, mowa
(kutchova) njuga, Kupembedza
mafano ndi kuombeza Maula,
(zonsezi) ndi uve, Mwa ntchito za
Satana. Choncho Zipeweni kuti
mupambane.
91. Ndithudi, Satana akufuna
kudzetsa Chidani ndi kusakondana
pakati Panu kudzera m'mowa ndi
Njuga, ndikuti akutsekerezeni
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 7 I 256 I V *>
o dJjlil ojj^
Kukumbukira Mulungu Ndi
kupemphera Swala. Kodi inu
simusiya?
92. Mverani Mulungu, ndipo
mverani Mtumiki wake ndipo
chenjerani (Musanyoze malamulo
a Mulungu). Ngati munyoza,
dziwani kuti udindo wa Mtumiki
wathu ndikufikitsa uthenga
Woonekera basi. (Ngati atafikitsa
Uthenga, palibe kudzudzulidwa iye)
93. Palibe tchimo kwa amene
akhulupirira Ndikuchita zabwino
pazomwe Adadya
(zisadaletsedwe) Ngati akupitiriza
kuopa ndikukhulupirira Ndikuchita
zabwino; kenako nkuopanso
(Ataletsedwa zina)
ndikukhulupirira; (Atalamulidwa
zinanso) nkuopanso Ndikuchita
zabwino. Ndipo Mulungu,
amakonda ochita zabwino.
94. E inu amene
mwakhulupirira! Ndithu Mulungu
Akuyesani ndi nyama zina
zozichita ulenje, zomwe Manja
anu ndi mikondo yanu ingazifikire,
kuti Mulungu amuwonetsere
poyera amene akumuopa
Mwanseri. Ndipo amene alumphe
malire (posaka Nyamayo ndi
kupha) pambuyo pazomwe
Mwauzidwazo, adzapeza chilango
chopweteka.
Surat 5. Ai-Ma'idah Juzu 7
257
V *j*-»
aJU'lil Ojj~t
95. E inu amene
mwakhulupirira! Musaphe nyama
Yamtchire pomwe inu muli
m'mapemphero a Haji Kapena
Umura. Ndipo amene angaphe
mwadala Nyama ya mtchireyo
mwa inu, dipo (lake likhale
Kuzinga) yofanana ndi yomwe
waphayo, mumtundu Wanyama
zowetedwa, (monga mmene)
angaweruzire Olungama awiri a
mwainu. Nyama yansembeyo
Iperekedwe ku Ka'aba (kuti
ikazingidwe kumeneko
Ndikuwagawira osauka); kapena
alipe dipo Lachakudya kudyetsa
masikini; kapena m'malo Mwake
asale kuti alawe kupweteka kwa
chinthu Chakecho. Ndipo Mulungu
afafaniza zomwe zidapita Kale.
Koma amene achitenso, Mulungu
amukhaulitsa Ndi chilango
chochokera kwa lye. Ndipo
Mulungu Ngwamphamvu zoposa,
Wokhaulitsa koopsa
96. Nkololezedwa kwa inu
kusaka nyama Zam'nyanja ndi
chakudya chake (chomwe
Chapezeka m'nyanjamo chitafa
chokha). Chimenecho ndi kamba
wanu (Inu amene simuli paulendo)
ndiponso Apaulendo.
Kwaletsedwa Kwa inu kusaka za
pamtunda Pomwe muli
m'mapemphero a Haji Kapena
Siirat 5. Al-Ma'idah Juzu 7
258
V *j*-i
OJtftil Ojj-j
Umura. Opani Mulungu Yemwe
kwa lye mudzasonkhanitsidwa.
97. Mulungu wapanga Ka'aba
kukhala nyumba Yopatulika,
ndikukhala pamalo popezera
zosowa Za anthu. Ndipo
adapanganso miyezi (inayi)
Yopatulika, ndikupereka nyama
zansembe ku Makka zovekedwa
makoza monga zisonyezo
(Kusonyeza kuti zikupita ku
Makka). Zonsezi Nkuti mudziwe
kuti Mulungu akudziwa
Zakumwamba ndi pansi, ndikuti
Mulungu Ngodziwa chilichonse.
98. Dziwani kuti ndithudi,
Mulungu Ngolanga Mwaukali.
Ndikutinso Mulungu Ngokhululuka
Kwabasi, Ngwachisoni.
99. Pamtumiki palibe china
koma Kufikitsa chabe (uthenga).
Ndipo Mulungu akudziwa zimene
Mukuzionetsera poyera ndi
Zimene mukuzibisa.
100. Nena (kwa aliyense kuti):
Zoipa ndi zabwino Sizingafanane
ngakhale Kutakusangalatsa
kuchuluka Kwa zoipazo
(usapendekere Kuchuluka
kwakeko); choncho Opani
Mulungu, ee! Inu eni Nzeru kuti
mupambane."
101. E inu amene
mwakhulupirira! Musamafunse za
m&d&^wSfci
iBJ^SESSa^®
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 7
259 V «jfci
O dJjlil djj-i
zinthu zomwe Zitasonyezedwa
kwa inu zikuipirani. Ndipo ngati
muzifunsa pomwe Qur'an
ikuvumbulutsidwa, zionetsedwa
kwa inu. Mulungu wakhululuka
zimenezo. Mulungu Ngokhululuka
kwabasi Ndiponso Ngoleza
102. Anthu amene adalipo kale
inu Musanadze, adazifunsapo
Zotere. Ndipo pachifukwa
chimenecho Adasanduka
osakhulupirira.
103. Mulungu sadaike
(kuletsedwa Kwamtundu
uliwonse) panyama Yotchedwa
Bahira, ngakhale Saiba, Wasila,
ngakhalenso Hami. Koma amene
sadakhulupirire Akumpekera
Mulungu bodza. Ndipo ambiri
aiwo Sagwiritsa ntchito nzeru
zawo.
104. Ndipo akauzidwa:
"Tadzani kuchilamulo Cha zomwe
Mulungu wavumbulutsa ndi
(zomwe Akunena) Mtumiki,"
Akunena: "Tikukwaniritsidwa ndi
zomwe tidawapeza nazo makolo
athu," Kodi chinkana kuti Makolo
awowo sadali kudziwa chinthu
Chilichonse ndipo sadali oongoka,
(Awatsatirabe)?
105. E inu amene
mwakhulupirira! Chimene chili
chofunika kwa inu ndi
\j?^jp$& t^* f y QUoS
><'^<&\SM$
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 7
260
V *j*-1
DJJlil d
dj^-*
Kudziganizira nokha. Ndipo
amene Asokera sangakupatseni
mavuto Ngati inu mutalungama.
Nonsenu Kobwerera kwanu nkwa
Mulungu basi. Choncho
adzakuuzani zimene mudali
kuchita.
106. E inu amene
mwakhulupirira! Pamene
chamfikira mmodzi wa inu
Chisonyezo cha imfa, ndipo
akufuna kusiya chilawo (Mawu
omaliza) funani Mboni ponena
mawuwo. Aikire umboni Awiri
olungama mwa inu (Asilamu)
Kapena apadera ngati muli
paulendo, ndipo Zisonyezo zaimfa
zitaonekera. Ngati mutazikaikira
Zitsekerezeni (kuti zisachoke)
mboni Ziwiri pambuyo pa Swala
(yomwe Amasonkhana anthu
ambiri), ndipo Zilumbirire m'dzina
la Mulungu kunena (Kuti):
"Sitikusinthanitsa Malumbirowa
ndi china chake ngakhale
Chitakhala chothandiza kwa ife
Kapena mmodzi mwa abale athu.
Sitikubisa umboni umene Mulungu
Watilamula kuti tiupereke moona.
Ife ngati titabisa umboni (kapena
Kuyankhula chonama), ndithudi
tikhala Mwa anthu ochimwa."
107. Koma ngati kutaoneka kuti
mboni Ziwiri zija zanama pa
umboni wawo, Kapena zabisa
Surat 5. AI-Ma'idah Juzu 7
261
V*>l
O Sjtflll
aj^
chinthu, apo awiri Achibale a
wakufayo aimirire m'malo Mwa
mboni ziwirizo, (pambuyo paswala
Kuti aulule zabodza lawo).
Choncho Alumbirire m'dzina la
Mulungu kuti: "Ndithu kulumbira
kwathu nkoyenera
Kuvomerezedwa kuposa
Kulumbira kwawo; ndipo
sitinapyole malire (Mukulumbira
kwathu). Ndipo sitikuzipekera
Mbonizo bodza. Ndithudi, ngati ife
Titachita zotere, ndiye kuti tikhala
Mwa ochita zoipa, (oyenera
kulandira Chilango cha
Mulungu)."
108. Chilamulochi ndi njira
yapafupi kuti Mboni zikwaniritse
umboni wawo mnjira Yoyenera,
(ndikuti zisamalire Kulumbira
Mulungu kwawo); kapena kuopa
Kuyaluka bodza lawo likaonekera
Poyera, pambuyo polumbira
enawo (Izi zili polumbira amlowa
mmalo pokana Umboni wawo).
Ndipo opani Mulungu
(mkulumbira kwanu Ndi
kukhulupirika kwanu) ndipo
Mverani malamulo Ake. Mulungu
Satsogolera anthu opandukira
chilamulo Chake.
109. (Kumbukirani) tsiku
lomwe Mulungu Adzasonkhanitsa,
aneneri Ndikuwafunsa kuti: "Kodi
Mudayankhidwa chiyani?"
X3\
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 7
262 V *>i
OJU'lil
Oj^
Aneneri adzati: "Ife sitidziwa
Ndithudi, inuyo Ndiye Wodziwa
zamseri."
110. Kumbukiraninso pamenne
Mulungu adzati: "Iwe Yesu
mwana wa Mariya! Kumbuka
chisomo Changa pa iwe ndi pa
mayi wako, pamene
Ndinakuthandiza ndi mzimu
woyera (Gabriel) Kotero kuti
udalankhula kwa anthu (mawu
Omveka) pamene udali mchikuta
ndiponso Pamene udali wamkulu.
Ndipo (kumbuka) pamene
Ndidakuphunzitsa kulemba ,
nzeru; (Ndinakuzindikiritsanso
Buku la) Taurat ndi Injili.
(Kumbukanso) pamene udaumba
dongo chithunzi Chambalame
mwalamulo langa. Utatero
udauziramo Ndipo zidasanduka
mbalame mwalamulo langa.
Ndipamene udali kuchiza akhungu
ndi akhate, Mwalamulo langa.
Ndipamene unkawatulutsa
(M'manda) enamwaakufa
mwalamulo langa. Ndipamene
ndinawatsekereza ana a Israeli kwa
iwe (Kuti asakuzunze) pamene
udawadzera ndi Zisonyezo
zooneka, ndipo aja mwaiwo omwe
Sadakhulupirire, adati: Ichi
sichina, koma ndi Matsenga
owonekera.
111. Ndipo (kumbukira)
pamene Ndidawaululira ophunzira
b&\$(&9\&&M$
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 7
263
V*>l
o *JJ\L\ i
9jf*
ako Kuti: "Ndikhulupirireni Ine
ndi Mtumiki wanga (uyu Yesu)."
Iwo adati: "Takhulupirira; ndipo
Khalani mboni kuti ife ndife
Ogonjera (tadzipereka mwa Inu)."
112. (Kumbukira) pamene
ophunzira ako adati : "I we, Yesu
mwana wa Mariya: Kodi Mbuye
Wako angathe kutitsitsira
chakudya kuchokera
Kumwamba?" (Yesu) adati:
"Opani Mulungu, ngati Inu mulidi
okhulupirira. (Musamangopempha
Zozizwitsa)."
113. (Iwo) adati: "Tikufuna
kudya Chimenecho, ndikuti mitima
yathu Ikhazikike, Ndikutinso
tidziwe Kuti watiuza choona; tero
kuti Tikhale oikira umboni
pachimenecho."
114. Yesu mwana wa Mariya
adati: "Inu, Mulungu Mbuye
wathu! Titsitsireni chakudya
kuchokera Kumwamba kuti
chikhale Chikondwerero cha
oyambirira Ndi omaliza mwa ife,
komanso Chikhale chisonyezo
chochokera Kwa inu; choncho
tipatseni Ndithu, inu ndinu abwino
Popatsa kuposa opatsa."
115. Mulungu adati: "Ndithu,
Ine Ndikuchitsitsa kwa inu. Koma
amene adzatsutse Mwa inu
pambuyo pa ichi, Ndithu, Ine
KV»^8K&%;
*?K 99
®(z&z
*\l<f ft < J '?*\Z.»"\ '
Siirat 5. Al-Ma'idah Juzu 7
264
V *>»
o Sju'lil Ijj^t
ndidzamulanga Ndi chilango
chomwe Sindidamulangepo nacho
Aliyense mwazolengedwa."
116. Ndipo (kumbukirani)
pamene Mulungu adzanena: "Iwe
Yesu mwana wa Mariya: Kodi iwe
udauza Anthu kuti," "Ndiyeseni
ine Ndi mayi wanga monga
Milungu iwiri m'malo mwa
Mulungu?" (Mneneri Yesu)
adzaati: "Ulemerero ukhale pa Inu.
Sikoyenera Kwa ine kunena
zomwe sizili Zoyenera (kwa ine
mawu amenewa Ngabodza). Ngati
ndikadanena, Ndiye kuti
mukadadziwa. Inu Mukudziwa
zomwe zili mumtima Mwanga,
pomwe ine sindidziwa Zomwe zili
mwa inu. Ndithudi, Inu ndinu
Wodziwa zamseri,
117. Sindinawuze chilichonse
kupatula Chimene mudandilamula
kuti; "Pembedzani Mulungu,
Mbuye wanga Ndiponso Mbuye
wanu". Ndipo ndinali Mboni kwa
iwo pamene ndidali nawo. Koma
pamene mudanditenga, Inu ndiye
Mudali muyang'aniri paiwo; ndipo
Inu ndinu Mboni yachilichonse.
118. "Ngati muwalanga,
ndithudi Iwo ndi akapolo anu.
Ndipo mukawakhululukira,
Ndithudi, inu ndinu Mwini
Mphamvu zoposa, Wanzeru
zakuya."
©y\yJ*S(^J
Surat 5. Al-Ma'idah Juzu 7 265 V *>i
OJJlil OjJ~"
119. Mulungu adzati: "Hi ndi
tsiku lomwe olankhula zoona
Kudzawathandiza kuona Kwawo.
Iwo adzalandira Minda yomwe
pansi ndi Patsogolo pake mitsinje
Ikuyenda. M'menemo Adzakhala
muyaya. Mulungu adzawayanja;
Naonso adzayanja zomwe
Adzapatsidwa ndi Mulungu.
Kumeneko ndiko kupambana
Kwakukulu.
120. Mulungu yekha ndiye
mwini ufumu Wakumwamba ndi
pansi, ndi Zam'menemo. lye
Ngokhoza Chilichonse.
*«? »'*" •»
S^VtfUPCW^
Surat 6. Al-An'am Juzu 7
266
V*>i
1 fUi*i|1 5jj-*»
SURAT AL-AN'AM VI
Surayi yalangiza anthu kuti alingalire dziko ndizammenemo,
zomwe zikusonyeza ukulu wa Muyambitsi; Mulungu
wolemekezeka. Ndi kuti palibe womthandiza mkulenga.
Ndiponso sathandizana ndi aliyense polandira mapemphero.
Ndiponso salingana ndi aliyense mwazolengedwa Zake.
M' surayi muli nkhani za ena mwa aneneri. Ndipo yayamba
kusimba nkhani ya Ibrahim (A.S.) Ndipo yanenetsa kuti iye
adamdziwa Mulungu kupyolera mkumpenyetsetsa molingalira
za chilengedwe cha zakumwamba monga nyenyezi, dzuwa ndi
mwezi.
Surayi ikuphanula maso a anthu kuti ayang'ane zinthu
momwe zikuchitikira; momwe chamoyo chimatulukira m'chakufa.
Ndipo yafotokozanso makhalidwe a anthu amakani, otsutsa kuti
amangokangamira maganizo okhala kutali ndi choonadi.
M'surayi mwafotokozedwanso zinthu zahalali ndi zaharamu.
Ndi kuti udindo wopanga chinthu kukhala chahalali kapena
haramu ngwa Mulungu. Ndipo m' Surayi mulinso malamulo
oletsa kupembedza mafano, kuchita chiwerewere, kupha anthu,
kudya chuma cha masiye, ndi kuti miyeso ndi masikero
ziyesedwe modzazitsa, kukwaniritsa chilungamo pamachitidwe
onse, kusunga chipangano ndi kuchitira zabwino makolo.
Surat 6. Al-An'am Juzu 7
267
V*>l
n fUoVi Sjj--
Surat Al-An'am VI
M^mmz''
m
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Kuyamikidwa konse
kwabwino nkwa Mulungu, Yemwe
adalenga thambo ndi Nthaka,
napanga mdima ndi kuunika,
Pamwamba pa izi, amene
sadakhulupirire Mbuye wawo
akumfanizira Mulungu ndi
Milungu yabodza.
2. lye ndi Yemwe adakulengani
ndi Dongo, ndipo kenako adaika
nthawi (Yothera cholengedwa
chilichonse), Ndi nthawi ina
yodziwika kwa lye (Yomwe
njoukitsira zolengedwa ku imfa).
Ndipo pa izi inu (osakhulupirira)
Mukukaikira.
3. Ndipo lye ndi Mulungu
(Wopembedzedwa) Kumwamba
ndi pansi. Akudziwa za Mkati
mwanu ndi zakunja kwanu, Ndipo
akudziwa zimene mukupeza
(Kuchokera mzochitachita zanu,
Zabwino kapena zoipa).
4. Ndipo palibe pamene
Chikuwadzera chisonyezo
Chilichonse mwa zisonyezo Za
Mbuye wawo koma
Akuzitembenukira kumbali.
Q&i&^Wj
-^
©<
x&
'\S-"J 9 \ 1*9%*?' ^'^'i
" 9 • 99X'>'
Surat 6. Al-An'am Juzu 7
268
V *>l
% fUiSH fljj-»
5. Ndithudi, atsutsa choonadi
(Qur'an) parnene Chawadzera.
Posachedwapa ziwafika Nkhani
(za zilango) zimene adali
Kuzichitira chipongwe.
6. Kodi saona kuti ndi mibadwo
ingati Tidaiononga patsogolo
pawo? Tidawapatsa mphamvu
yopezera za M'dziko zomwe
sitidakupatseni inu Ndipo
tidawavumbwitsira mvula
Yopitiriza (mwaubwino choncho,
Adasangalala kopambana). Ndipo
Tidaipanga mitsinje kuyenda pansi
Pawo (pansi pa mitengo yawo ndi
Nyumba zawo). Kenako
tidawaononga Chifukwa cha
machimo awo, ndipo Pambuyo
pawo tidalenga mibadwo ina.
7. Ndipo ngati tikadakutsitsira
Malemba (olembedwa)
m'mapepala, (Monga momwe
adakufunsira), nkuwakhudza Ndi
manja awo, amene Sadakhulupirire
akadati: "Ichi sichina koma ndi
matsenga owoneka."
8. Ndipo amanena: "Bwanji iye
Osamtsitsira Mngelo (kuti Aziikira
umboni kwa anthu za Uneneri
wake)?" Tikadakutsitsira Mngelo
(nkusakhulupirira), Ndithu,
chiweruzo chakuonongeka Kwawo
chikadakwaniritsidwa. Ndipo
Sakadapatsidwanso mpata.
Siirat 6. AI-An'am Juzu 7
269 V *>i
*\ {\*iH\ 5jj-»
9. Ndipo tikadampanga Mngelo
kukhala M'tumiki,
tikadamsandutsa kukhala Munthu
(chifukwa iwo sangathe Kumuona
Mngelo), ndipo tikadati
Asakanikirane nawo monga
Momwe eni amasakanikirana
(kotero Kuti sakadamdziwa kuti
Mngelo ndi uyu).
lO.Ndithudi, adachitidwa
chipongwe Atumiki patsogolo
pako; koma (Mapeto ake) aja mwa
iwo omwe Adachita chipongwe
zidawazinga Zomwe adali
kuzichitira chipongwe.
ll.Nena: "Yendani pa dziko,
kenako tayang'anani momwe
adalili mapeto Aotsutsa." 1
12. Nena (mowafunsa):
"Nzayani zomwe Zili kumwamba
ndi pansi?" Nena Kwa iwo (ngati
sakuyankha): "Nza Mulungu". lye
wadzikakamiza Kuwachitira
chifundo (anthu Ake).
(Pachifukwa chimenechi
amawapatsa Nthawi osawalanga
mwachangu). Ndithudi
adzakusonkhanitsani Tsiku la
Kiyama lopanda chikaiko. Amene
Adzitaya okha, sakhulupirira (Za
tsikulo).
* 9 J %' fX » <■*
1 Apa tanthauzo nkuti tayendani padziko mukayang'ane ndi kulingalira zilango
zopweteka zimene zldawatsikira anthu akale. Kuyang'ana ndi kulingalira
zoterezo kuti zikhale phunziro kwa inu kuti musachitenso zimene
zidawagwetsa kuchionongeko.
Siirat 6. Al-An'am Juzu 7
270
V *>i
*\ ^ usSh 5jj~>
13.Nza lye (Mulungu) Zonse
zili munthawi Ya usiku ndi usana.
lye Ngwakumva, Ngodziwa."
14.Nena: "Ndidzipangire
mtetezi Wanga kusiya Mulungu,
Mlengi Wathambo ndi nthaka? lye
Njemwe Amadyetsa ndipo
sadyetsedwa." Nena:
"Ndalamulidwa kukhala Woyamba
mwa olowa M'chisilamu," Ndipo
(ndauzidwa kuti): "Usakhale mwa
ophatikiza (Mulungu Ndi
mafano)"
15. Nena (kwa iwo): "Ine
ndikuopa chilango Cha tsiku
lalikulu Ngati ndinyoza Mbuye
wanga."
16. Yemwe adzapewetsedwe
(Chilangocho) tsiku limenelo,
Ndiye kuti wamchitira chifundo;
Kumeneko nkupambana
kowonekera.
17. "Ngati Mulungu
atakukhudza ndi Mazunzo, palibe
aliyense angathe Kukuchotsera,
koma lye basi; ndipo Ngati
atakukhudza ndi zabwino (palibe
Amene angakutsekereze ku
Zabwinozo). lye ali ndi mphamvu
paChilichonse. 1
1 Mu aya iyi Chauta akuuza Mtumiki Wake ndi omtsatira ake kuti ngati
masautso atampeza umphawi ndi matenda, palibe amene angamchotsere
zimenezi koma Mulungu basi. Ndiponso ngati zitamkhudza zabwino, monga
kukhala ndi moyo wangwiro ndi chuma chambiri, palibe amene angazichotse
zimenezi kwa iye ngati Mulungu safuna. Choncho tiyeni tiike chikhulupiriro
chathu chonse mwa Mulungu.
*±l' '*Z<* *9*99* 9 S919*
Surat 6. AI-An'am Juzu 7
271 I V *>»
*\ f UiSfi 3jj-»
18. lye ndi Mgonjetsi pa anthu
ake (Onse); lye Ngwanzeru
zakuya, Wodziwa nkhani zonse.
19.Nena: "Kodi nchinthu chanji
chomwe Umboni wake uli
waukulu koposa?"Nena (ngati
sakuyankha) : "Ndi (umboni Wa)
Mulungu basi. (lye) ndi mboni
Pakati pa ine ndi inu. Ndipo
Qur'an iyi yavumbulutsidwa kwa
ine Kuti ndikuchenjezeni nayo ndi
amene Yawafika (pali ponse
pamene ali). Kodi inu
mukutsimikiza ndi kuikira Umboni
kuti pali milungu ina Pamodzi ndi
Mulungu?" Nenanso: "Koma ine
sindikuikira umboni." Nenanso:
"lye ndi Mulungu mmodzi Yekha.
Ndithudi, ine ndili kutali ndi
zomwe mukumphatikiza nazo."
20. Omwe tidawapatsa Buku
akumzindikira
(Muhammad{SAW} bwinobwino)
monga Momwe akuwazindikirira
ana awo. Koma omwe adziononga
okha, iwo Sangakhulupirire.
21. Kodi ndani woipitsitsa zedi
Woposa yemwe akum'pekera
Mulungu bodza. Kapena kutsutsa
Zizindikiro zake? Ndithudi, oipa
sangapambane.
22. Ndipo (akumbutse) tsiku
lomwe Tidzawasonkhanitsa onse
pamodzi ;Kenako tidzati kwa
Surat 6. AI-An'am Juzu 7
272 V *>i
*\ pUity 5jj~*
omwe adali Kuphatikiza (Mulungu
ndi mafano): "Ali kuti aphatikizi
anu aja omwe Munkati
ngothandizana ndi Mulungu?"
23. Ndipo dandaulo lawo
silidzakhala Lina koma kunena:
"Wallahi,Tikulumbirira Mulungu
Mbuye Wathu, sitidali ophatikiza
mafano Ndi Mulungu." (Uku
kudzakhala Kuyesera kumunamiza
Mulungu).
24. Taona momwe
akudzinamizira okha Ndipo
zidzawataika zomwe adali Kuzipeka
(ponena kuti izo ndi Milungu
zidzawapulumutsa Kwa Mulungu).
25. Alipo ena mwa iwo omwe
akukumvetsera (Ukamawerenga
Qur'an) ndipo taika Zitsekero
pamitima yawo kuti Asazindikire
(chifukwa cha machimo Awo
omwe akhala akuchita). Ndi
M'makutu mwawo kulemera kwa
ugonthi;Ndipo akaona chozizwitsa
chilichonse,Sakuchikhulupirira,Ku
fikira akakudzera kudzakangana
nawe.Awo amene sadakhulupirire
akuti:"Izi (zimene utilankhulazi),
Sikanthu koma ndi nkhani zopeka
Za anthu akale."
26. Ndipo iwo akuletsa (anthu
kutsatira) izi, Ndipo (eniwo)
akudziika nazo kutali. Palibe Wina
akumuononga koma iwo okha,
asakudziwa.
9 V*i 9 C 'K 9 *" K>' *9'\'*?'
Surat 6. Al-An'am Juzu 7
273
V*>i
% f toty *jj~*
27. Ndipo ukadaona (tsiku la
Kiyama) Pamene adzawaimitsa
pamoto Nkuyamba kunena: "Ha!
Tikadabwezedwa (kudziko
lapansi) Ndipo sitikadatsutsanso
zizindikiro Za Mbuye wathu;
tikadakhala mwa Okhulupirira"
(Ukadaona tsikulo M'mene
azikasinkhirasinkhira Atathedwa
nzeru).
28. (Sichoncho sadzachita
chilichonse Chabwino.) Koma
zawaonekera poyera Zomwe adali
kubisa kale. Ndipo
Akadabwezedwa akadabwerezanso
Kuchita zimene adaletsedwa.
Ndithudi Iwo ngabodza basi.
29. Akumanena: "Palibe china
koma Moyo wathu wapadziko
lapansi basi. Ndipo ife
sitidzaukitsidwanso M'manda".
30. Ndipo ukadaona (tsiku la
chiweruzo) Pamene
azikaimitsidwa pamaso pa Mbuye
wawo nauzidwa: "Kodi ichi
Sichoona?" (Iwo) nati: "Inde
Nchoona: tikulumbira Mbuye
Wathu." (Mulungu) adzati:
"Lawani chilango chifiikwa Cha
kusakhulupirira kwanu kuja
(Aneneri a Mulungu)."
31. Ndithudi, ataika ndi
kuonongeka Amene akutsutsa
zokumana ndi Mulungu, mpaka
iV- » "»■*».! v^t2t<s »>1i-"' V
Surat 6. AI-An'am Juzu 7 I 274 1 V *j*-»
1 f\juH\ 5jj-»
mwadzidzidzi nthawi Ya kiyama
itawafikira ndipo nati: "Ho!
Masautso paife chifukwa
chakusalabadira kwathu kuja."
Uku iwoAtasenza mitolo
yamachimo kumisana Kwao.
Taonani kuipa kwa zomwe
akusenza.
32. Ndipo moyo wadziko lino
lapansi Sikanthu, koma ndi
masewera (chibwana). Ndiponso
chabe. Koma nyumba Yomaliza
ndi yabwino koposa,(Siyofanana
ndi chisangalalo Chapadziko
lapansi) kwa omwe Akuopa
Mulungu. Bwanji simuzindikira?
33. Ndithu, tikudziwa kuti
zikukudandaulitsa zomwe
akukunenera (Pokunyoza ndi
kukuyesa wabodza).Iwo sakutsutsa
iwe; koma oipawa Akutsutsa
zizindikiro za Mulungu.
34. Ndithudi, Aneneri onse
adatsutsidwa Iwe usadadze. Koma
adapirira Kuzomwe adatsutsidwa,
ndipo Adazunzidwa kufikira
pamene Chipulumutso chathu
chidawafika. Palibe wosintha
mawu a Mulungu (Malonjezo a
Mulungu). Ndithu, Zakufika
nkhani za Atumiki (Momwe muli
malingaliro ndi Maphunziro
ambiri).
35. Ndipo ngati nkovuta kwa
iwe kudzipatula Kwawoku (ndi
>> JLf It ' \ 9X9 \'\ 9 V\$ K'
$$&$&&&&
Surat 6. AI-An'am Juzu 7
275
V*>i
*\ pUity 5jj->
zomwe wadza nazozi Pomwe iwo
akukuumiriza kuti uwabweretsere
Chozizwitsa, nawe Nkumafuna;
zikadatero, pomwe Ine
Sindikufuna); choncho, ngati uli
Wokhoza kufunafuna njira yapansi
Penipeni m'nthaka (kukafuna
Zozizwitsazo), kapena (ungathe
Kupeza) makwerero nkukwera
kumwamba nkubwera ndi
chozizwitsa (Chimene akufuna,
chita). Mulungu Akadafuna
akadawasonkhanitsa onse
Kuchiwongoko. Choncho,
usakhale Mwa osazindikira zinthu.
36. Ndithudi amene
akuvomereza, ngomwe akumva.
(Ndipo anthu awa amene safuna
Kumvera chilichonse ndi akufa
Ngakhale ali moyo). Ndipo akufa
Mulungu Adzawaukitsa (m'manda
mwawo) kenako Adzabwezedwa
kwa lye.
37. Ndipo (iwo) akumanena:
"Bwanji Sichinatsitsidwe
chozizwitsa kwa iye Kuchokera
kwa Mbuye wake?" Nena:
"Ndithudi, Mulungu Ngokhoza
kutsitsa Chozizwitsa koma ambiri
aiwo sadziwa (Zomwe Mulungu
afuna)."
38. Ndipo palibe nyama ili
yonse M'nthaka, ngakhale
mbalame yowuluka Ndi mapiko
ake awiri koma ndi magulu
<j££ll L$& JJ&5 $<£&1\
Surat 6. Al-An'am Juzu 7
276
V *>l
n pUity djj-j
Azolengedwa ngati inu (Zomwe
Mulungu adazilenga). Sitinasiye
chinthu chilichonse Kapena
kuchinyozera chilichonse M'Buku
(chomwe nchofunika Koma
tachifotokoza).Ndipo tero
adzawasonkhanitsa Kwa Mbuye
wawo.
39. Ndipo amene atsutsa
zizindikiro Zathu, ndi agonthi
ndiponso Abubu, ali mum'dima
(waumbuli).Amene Mulungu
wafuna kumlekereraKusokera,
(amasokera). Ndipo amene
wamfuna amamuika Panjira
yolunjika (yomwe Ndi njira ya
Chisilamu).
40. Nena: "Tandiuzani ngati
mazunzo A Mulungu atakufikani
(pompano Padziko lapansi),
kapena kukufikani Nthawi
(yachilango cha tsiku Lomaliza)
Kodi mudzaitana yemwe Sali
Mulungu (kuti akupulumutseni)?
Ngati inu muli oona.
41. Koma lye yekha ndi Yemwe
mudzampempha, Ndipo lye
adzakuchotserani Zomwe
mukumpempha (kuti
Akuchotsereni) ngati
atafuna.Ndipo mudzaiwala zomwe
mudali Kuziphatikiza (ndi
Mulungu)."
42. Ndithu, tidawatumiza
(Atumiki) kumibadwo yomwe
^gf^^it^M
a&rfriii*'
'?6&&$&4Q&'&J
wr-v
Surat 6. Al-An'am Juzu 7
277 V *>i
*\ fbuty 5jj-*
idalipo iwe usadadze. Ndipo
tidawakhaulitsa ndi mazunzo ndi
masautso kuti iwo adzichepetse
(pambuyo podzikuza).
43. Pamene masautso adawafika
kuchokera Kwa Ife, bwanji
sadaphunzire Kudzichepetsa?
Koma mitima yawo Idali youma,
ndipo SatanaAdawakometsera
machimo omwe Iwo adali kuchita.
44. Ndipo pamene adanyozera
zimene ankakumbutsidwa
tidawatsekulira Makomo a chinthu
chilichonse(Chimene adali
kuchifuna) kufikira Pamene
adasangalala ndi zomwe
Adapatsidwa, tidawagwira
Mwadzidzidzi; pompo adataya
mtima.
45. Ndipo mizu ya anthu oipa
idadulidwa.Kuyamikidwa konse
kwabwino nkwa Mulungu, Mbuye
wa zolengedwa.
46.Nena: "Tandiuzani, ngati
Mulungu atakuchotserani kumva
kwanu ndi Kupenya kwanu,
nadinda chidindo M' mitima yanu
(kuti asalowemo mawu
Amalangizo amtundu uliwonse),
Kodi ndi mulungu uti, kupatula
Allah, amene angakubwezereninso
(Zimenezi)?" Taona momwe
Tikufotokozera mwatsatanetsatane
Zizindikiro kenako iwo akunyozera.
*&&!&SM%$i
Surat 6. AI-An'am Juzu 7
278
V *>i
*\ pUity 5jj-»
47. Nena: "Tandiuzani, ngati
masautso a Mulungu atakufikani
mwadzidzidzi Kapena moonekera,
kodi angaonongeke Ndi ena osati
anthu ochita zoipa?
48. Ndipo sititumiza atumiki
koma Kuti akhale ouza nkhani
zabwino Ndi ochenjeza. Choncho
amene akhulupirira nakonza
zinthu,Pa iwo sipadzakhala mantha
ndiponso Sadzadandaula.
49. Ndipo amene atsutsa
zizindikiro Zathu, chilango
chidzawakhudza Chifukwa
chakupandukira Kwawo
chilamulo.
50. Nena: "Ine sindikukuuzani
kuti Ndili nazo nkhokwe (za
zabwino za Mulungu Kotero kuti
nkukupatsani chimene Mwafuna).
Ndipo (sindikukuuzani) Kuti
ndikudziwa zamseri, (Za Mulungu
kotero kuti nkukufotokozerani
zomwe zingakufikeni Pamalonda
anu monga momwe mwafunira
Kuti ndikuuzeni.) Ndiponso
Sindikukuuzani kuti ine ndine
mngelo (Nkumandifunsa kuti,
"Bwanji Ukudya pomwe uli
mngelo?") Ine Sinditsata china
koma zomwe Zikuvumbulutsidwa
kwa ine. Nena:"Kodi wakhungu
ndi wopenya Angafanane? Bwanji
simukuganizira?"
«jj
9 >i.
Surat 6. Al-An'am Juzu 7
279
V frjA-i
*\ pbuty $jj->
51. Achenjeze ndi Qur'an iyi
omwe Akuopa kuti
adzasonkhanitsidwa kwa Mbuye
wawo pomwe ali opanda Mtetezi
ngakhale muomboli Aliyense
kupatula lye, kuti iwo aope
(Mulungu).
52. Ndipo usawathamangitse
omwe akupembedza Mbuye wawo
m'mawa ndi Madzulo pofuna
chiyanjo chake.Chiwerengero
chawo sichili pa iwe ngakhale
pang'ono, ndipo chiwerengero
chako sichili pa iwo ngakhale
pang'ono kotero kuti
Nkwathamangitsa. (Ngati
uwapirikitsa) Ukhala m'gulu la
anthu ochita zoipa.
53. Ndipo momwemo
tawasankha ena (osauka) Kukhala
mayeso a ena (olemera) kuti
(osauka) anene: "Kodi awa ndi
omwe Mulungu wawasankhira
ubwino mwa ife (Ndikutisiya ife?
Hi ndi bodza Sichipembezo
choona, podziwa iwo ubwino
Wake ife tisanawudziwe)." Kodi
Mulungu sadziwa amene
akumthokoza?
54. Ndipo (iwe Mneneri)
akakudzera (awo Osauka) amene
akhulupirira zizindikiro Zathu
(atalakwa pang'ono), auze:
"Mtendere Ukhale pa inu. Mbuye
Surat 6. Al-An'am Juzu 7
280
V *>i
*\ ^UuSfl 0jj-*»
wanu wadzikakamiza Kukhala
wachifundo kuti mwa inu amene
achite choipa mwaumbuli, koma
pambuyo pake nkulapa, nachita
zabwino, Mulungu
Amkhululukira; lye Ngokhululuka
Kwambiri, Ngwachisoni."
55. Mmenemo ndi momwe
tikufotokozera Zizindikiro
mwatsatanetsatane(kuti Choonadi
chioneke) ndi kuti njira ya oipa
idziwike bwinobwino.
56. Nena: "Ine ndaletsedwa
Kupembedza amene
Mukuwapembedza kusiya
Mulungu." Nena: "Sinditsata
zilakolako zanu; Ndikadatero
ndikadasokera Ndipo
sindikadakhala mwa
Otsogozedwa".
57. Nena: "Ine ndili ndi
chisonyezo Chooneka chochokera
kwa Mbuye wanga (Chotsimikizira
zomwe ndikunenazi). Koma inu
mwachitsutsa. Ndilibe(Chilango)
chimene
mukuchifulumizitsacho.Palibe
kulamula koma Nkwa Mulungu.
Amakamba zoona Zokhazokha;
lye Ngwabwino Polamula kuposa
olamula (onse)."
58. Nena: "Ndikadakhala nazo
zimene Mukuzifulumizitsazo,
ndiye kuti Zikadachitika pakati
8U8&V&1&&$@
Z&&S3a* l $l&&&ti&
@£&&£$\
Surat 6. AI-An'am Juzu 7
281
V*>i
*\ fUuSfi *jj~*
paine Ndi inu
(ndikadakakuonongani Koma
ndilibe nyonga). Ndipo Mulungu
akuwadziwa bwino anthu Ochita
zoipa."
59. Ndipo lye (Mulungu) ali
nawo Makiyi azobisika palibe
Akuwadziwa koma lye basi. Ndipo
Akudziwa zapamtunda ndi za
Panyanja. Ndipo palibe tsamba
Limene limagwa koma
amalidziwa. Ndipo (siigwa) njere
mumdima wa M'nthaka (koma iye
akudziwa). Ndipo (sichigwa)
chachiwisi Ngakhale chouma,
koma chili M'Buku loonetsa
chilichonse.
60. Iye ndiyemwe amakupatsani
imfa (Yatulo) nthawi yausiku,
ndipo Amadziwa zimene mwachita
masana,Kenako amakudzutsani
usana kuti Ikwane nthawi yanu
yoikidwa (yofera); Kenako kwa
Iye ndiko Kobwerera kwanu,
nadzakuuzani Zimene munkachita.
61. Iye Ngopambana Yemwe ali
pamwamba Pa akapolo Ake ndipo
akutumizirani (Angelo) osunga,
(olemba zochita Zanu); kufikira
mmodzi wanu imfa Ikamdzera,
angelo athuwo amampatsa imfa,
Ndipo iwo sanyozera (ntchito
yawo).
62. Kenako adzabwezedwa kwa
Mulungu,Mbuye wawo Woona.
©
'•• > " v
W$W2^W%&
Surat 6. Al-An'am Juzu 7
282
V^i
1 pUity
>J>-
Dziwani kuti Kuweruza Nkwake.
lye ngwachangu Powerengera
kuposa owerengera (onse).
63. Nena: "Kodi ndani
Amakupulumutsani M'masautso
apamtunda ndi panyanja?"
Mumampempha modzichepetsa
ndi motsitsa mawu (kuti): "Ngati
atipulumutsa (m'mazunzo awa,)
Ndithudi tidzakhala mwa
othokoza."
64. Nena: "Mulungu ndi
Yemwe Amakupulumutsani
kuzimenezo ndi Kumasautso
amtundu uliwonse.Kenako inu
mukumphatikiza (Ndi mafano)
65. Nena: "lye Ngokhoza
kukutumizirani Chilango
kuchokera pamwamba panu
Kapena pansi pamiyendo yanu,
kapena Kudzetsa chisokonezo
(Nkukhala) magulumagulu
(osamvana), Ndipo (akhoza)
kuwalawitsa ena ainu Chilango
chamtopola wa ena." Taona
Momwe tikufotokozera zizindikiro
Kuti iwo azindikire.
66. Koma anthu ako aitsutsa
Qur'an iyi Pomwe ili yoona.
Nena: "Ine sindili kapitawo painu."
67. Nkhani iliyonse (yomwe
yatchulidwa Apa) ili ndi nthawi
yake yodziwika (Yofikira). Ndipo
posachedwapa Mudziwa (izi).
&&&&&&&&
a
'4*
Surat 6. Al-An'am Juzu 7
283 I V *>»
1 f Uity 3jj--
68. Ndipo (iwe Msilamu
weniweni) ukawaona omwe
Akuchita chipongwe ndi aya
Zathu, apatuke mpaka Anene
nkhani ina. Ngati Satana
atakuiwalitsa, (Nkukhala nawo
pomwe iwo akukambirana Zotere),
choncho, pambuyo pokumbuka
usakhale Pamodzi ndi anthu ochita
zoipa.
69. Palibe chilichonse chimene
chingawapeze oopa Mulungu
chochokera m'chiwerengero cha
oipawo, Koma chofunika kwa iwo
(oopa Mulungu)
Ndikuwakumbutsa (oipawo) kuti
aope (Aleke zomwe akunenazo).
70. Asiye amene achita
chipembedzo Chawo kukhala
masewera ndi chibwana. Ndipo
wawanyenga moyo Wadziko
lapansi. Choncho, akumbutse Ndi
Qur'aniyo (kuti achenjere), kuti
Ungaonongedwe mtima uliwonse
(ndi Kuikidwa m'ndende)
kupyolera muzomwe Udapata.
Ndipo sukhala ndi Mtetezi
ngakhale muomboli posakhala
Mulungu, ngakhale utayesera
kupereka Dipo lamtundu uliwonse
silingavomerezedwe (kwa
mzimuwo). Awo ndi omwe
aonongeka ndi kunjatidwa
Chifukwa chazomwe adapeza. Iwo
adzakhala ndi chakumwa
,9 * ,* \9K9l' )i'999* 9 ><•
OoO
Surat 6. Al-An'am Juzu 7
284
V»>i
*\ ^UiSH OjJ-»
chamadzi a moto kwambiri, ndi
chilango chopweteka chifukwa cha
kusakhulupirira Kwawo
(Mulungu).
71.Nena: "Kodi tipembedze
omwe sali Mulungu, omwe
sangatipatse phindu (Ngati
titawapembedza), ndiponso
Sangathe kutivutitsa (tikasiya
kuwapembedza), Natibwezedwa
m'mbuyo pambuyo potitsogolera
Mulungu? tikhale chimodzimodzi
aja omwe Satana Adawasokeretsa,
nkukhala achewuchewu Padziko?
AH nawo anzawo omwe
akuwaitanira Kuchiongoko (kuti)
"Bwerani kwathu, (Koma
samva,sitingakhale monga anthu
otere)." Nena:"Utsogozi weniweni
ngwa Mulungu, ndipo
Talamulidwa kuti tigonjere Mbuye
wa zolengedwa;
72. Ndiponso (atiuza kuti:)
"Pempherani Swala, Muopeni lye
yemwe kwa lye
Mudzasonkhanitsidwa."
73. lye ndiye adalenga Thambo
ndi nthaka Mwachoonadi. Ndipo
Panthawi imene akunena
(Kuchiuza chinthu):
"Chitika",Ndipo chimachitikadi.
Mawu ake ndioona. Ndipo Ufumu
udzakhala Wakewake tsiku limene
Lipenga lidzaimbidwa. Ngodziwa
Surat 6. Al-An'am Juzu 7
285 V *>i
% fU^T
\ i
jj~*
zamseri ndi zooneka. lye
Ngwanzeru zakuya,Wodziwa
nkhani zonse.
74. Ndipo (kumbukirani)
Ibrahim pamene Adauza bambo
ake, Azara: "Kodi Mukupanga
mafano kukhala milungu? Ndithu,
Ine ndikukuonani inu ndi anthu
anu Kuti muli m'kusokera
koonekera."
75. Ndipo momwemo
tidamuonetsa Ibrahim ufumu
wakumwamba Ndi pansi (kuti
ngwa Mulungu)Kuti akhale
m'modzi mwaotsimikiza.
76. Ndipo pamene kunam'dera
adaona nyenyezi.Adati
(mwadaladala kuti abutse nzeru Za
opembedza mafano): "(Nyenyezi)
iyi ndiye Mbuye wanga." Pamene
idalowa, adati: "Sindikonda
(Milungu) yomalowa, (yomasowa,
yakutha)"
77. Pamene adaona mwezi
ukutuluka, Adati: u Uyu ndiye
mbuye wanga." Koma pamene
udalowa, adati: "Ngati Mbuye
wanga sandiongolera,
ndithudi,Ndikhala m'gulu la anthu
osokera."
78. Pamene adaona dzuwa
likutuluka, Adati: "Uyu ndiye
mbuye wanga; Uyu ngwamkulu
kwabasi." Koma Pamene lidalowa,
#3?
Surat 6. AI-An'am Juzu 7
286
V *>■!
n f UiSH 5jj-*
adati: "E inu anthu anga! Ine ndili
Kutali ndi zomwe
Mukumphatikiza nazo Mulungu
79. Ndithu ine ndalungamitsa
nkhope yanga Kwa yemwe
adalenga thambo ndi nthaka,
Ndapendekera kwa lye yekha.
Ndipo Ine sindili
mwaom'phatikiza Mulungu Ndi
mafano.
80. Ndipo anthu ake
adakangana naye (Pomuuzakuti:
"Bwanji ukusiya Chipembedzo
chamakolo ako; uona Malaulo."
lye) adati: "Kodi Mukukangana
nane pa za Mulungu Pomwe lye
wanditsogolera? Ndipo
Sindingaope zimene
mukumphatikiza Naye, kupatula
Mbuye wanga akafuna Chinthu,
(apo chiyenera kuchitika). Mbuye
wanga akudziwa chinthu
Chilichonse bwinobwino. Nanga
Kodi simumva ulaliki? (Bwanji
Simulalikika?")
81. "Ndipo ndingaope chotani
zomwe Mwaziphatikiza (ndi
Mulungu) pomwe Inu simuopa
kuti mukumphatikiza Mulungu
(ndi mafano) omwe Mulungu
Sadawatsitsire pa inu umboni (kuti
Muziwapembedza). Choncho ndi
gulu Liti m'magulu awa awiri
(langa Kapena lanu) loyenera
©<£$
o^3$tf<ji
fy&\£8tySfrM
(^*Xj5
Surat 6. Al-An'am Juzu 7
287
V *>i
1 fbuSfl OjJ-*»
koposa Kupeza chitetezo? Ngati
inu Mudziwa (zinthu).
82. (Palibe chikaiko kwa)
amene Adakhulupirira ndipo
nkusasakaniza Chikhulupiriro
chawo ndi shiriki (Kupembedza
mafano), iwowo ali Nacho
chitetezo. Ndiponso iwo Ndi
omwe ali oongoka.
83. Ndipo izi ndi (zina mwa)
zizindikiro Zathu (mitsutso yathu),
zomwe Tidampatsa Ibrahim pa
anthu ake. Timamtukulira
ulemerero amene Tamfuna.
Ndithu, Mbuye wako Ngwanzeru
zakuya, Ngodziwa Kwambiri.
84. Ndipo tidampatsa (Ibrahim
mwana Wotchedwa) Isihaka ndi
(mdzukulu Wotchedwa) Yakubu.
Onse tidawaongola. Nayenso Nuhi
tidamuongola kale (Asadadze
Mneneri Ibrahim). Ndipo
Kuchokera m'mbumba yake (Nuhi,
Tidamuongola) Daudi, Sulaiman,
Ayubu, Yusufu, Musa, ndi
Haaruna. Ndipo umo ndi momwe
Timawalipirira ochita zabwino.
85. Tidamutsogoleranso
Zakariya, Yahaya, Isa ndi Illiyasi.
Onse adali mwa Anthu abwino.
86. Ndi Ismail, Elisha, Yunusu
(Yona) ndi Luti (Loti). Onsewa
tidawapatsa Ubwino pazolengedwa
(pa anthu).
Surat 6. AI-An'am Juzu 7
288 V >>
*\ f Uity Sjj-"
87. (Ndiponso tidawatsogolera)
Ena mwa atate awo, Ana awo ndi
abale awo. Ndipo tidawasankha
ndi Kuwaongolera ku Njira
yolunjika.
88. Ichi ndi chiongoko cha
Mulungu. Ndi icho akuongolera
yemwe wamfuna Mwa anthu ake
(chifukwa Chosamphatikiza ndi
mafano).Akadakhala kuti
(aneneriwo)Adamphatikiza (ndi
zina) Zikadawaonongekera zimene
ankachita.
89. Iwo ndi omwe tidawapatsa
mabuku, Chiweruzo, ndi uneneri.
Ngati Awa osakhulupirira azikane
izi, Basi, tazipereka kale kwa
Anthu omwe sangazikane.
90. Iwo ndi omwe Mulungu
adawaongola Choncho, tsatira
chiongoko chawo. Nena:
"Sindikukupemphani malipiro
Paizi (zomwe
ndikukuphunzitsanizi, Koma
ndikungotumikira Mulungu). Ichi
sichina koma ndi ulaliki kwa
Zolengedwa (majini ndi wanthu).
91. Koma (Ayuda)
sadamulemekeze Mulungu monga
momwe zikufunikira
Pomulemekeza pomwe adati:
"Mulungu Sadavumbulutsepo
chilichonse kwa munthu
Aliyense." (Adanena izi pamene
&
Surat 6. Al-An'am Juzu 7
289 V ^
\ fUity Ojj-*.
mtumiki Adawauza kuti Qur'an
ndi buku lomwe Mulungu
wavumbulutsa). Nena: "Kodi
ndani Adavumbulutsa Buku
lomwe lidadza ndi Musa? Lomwe
lidali kuunika ndi chiwongoko
kwa Anthu, lomwe mwalipanga
kukhala zigawo-Zigawo; zimene
mwafuna kuonetsa kwa anthu
Mukuzionetsa. Koma zambiri
mukubisa (zomwe Sizigwirizana
ndi zofuna zanu).Ndipo
Mwaphunzitsidwa (ndi iyi Qur'an)
zomwe Simudali kuzidziwa, inu
ngakhale makolo anu. Nena:
"Mulungu (ndi Yemwe
wavumbulutsa Iyi Qur'an ndi
mabuku ena" ) .Kenako asiye
Azingosewera m'kubwebweta
kwawo (Kopanda pake).
92.Ndipo iyi Qur'an ndi Buku
limene Talivumbulutsa lamadalitso
ochuluka; Ndipo likutsimikizira
zomwe Zidalitsogolera. Ndikuti
uchenjeze Anthu a'mchimake cha
mizinda (Makka) ndi anthu omwe
ali M'mphepete mwake. Ndipo
Amene akukhulupirira tsiku
Lomaliza, akulikhulupirira
(Bukuli). Ndipo iwo Swala Zawo
akuzisunga bwino.
93. Kodi ndani woipitsitsa
koposa yemwe Wampekera bodza
Mulungu kapena wonena:
"Wandininkha" (chivumbulutso)
Surat 6. Al-An'am Juzu 7
290
V^jJH
*\ fbuSM $j>->
pomwe Sichidavumbulutsidwe
Kwa iye chilichonse; ndiyemwe
Akunena: "Ndivumbulutsa monga
chimene Mulungu wavumbulutsa."
Ukadawaona anthu Ochita zoipa
akuthatha ndi imfa, nawo angelo
atawatambasula manjaawo
(ndikuwauza:) "Tulutsani moyo
wanu; lero mulipidwa Chilango
chonyozeka chifukwa cha Zomwe
mudali kunenera Mulungu
popanda choonadi, Ndi
kudzitukumula kwanu pa
Zizindikiro zake".
94. Ndipo (tsiku lakiyama
tidzakuuzani): "Ndithudi,
mwatidzera mmodzimmodzi
(Payekhapayekha popanda chuma
ndi Ana kuti akupulumutseni),
monga mmene Tidakulengerani
pachiyambi. Ndipo mwasiya
Kumbuyo kwanu zonse zomwe
tidakupatsani. Ndipo sitikuona
pamodzi nanu apulumutsi anu aja,
Amene munkati ngothandizana
(ndi Mulungu; ndi Kuti iwo ndi
apulumutsi anu). Ndithudi
(mgwirizano) Omwe udali pakati
panu waduka. Ndipo Zakutaikirani
zimene Munkaziganizira (kuti ndi
milungu)."
95. Ndithu Mulungu ndi
Yemwe amang'amba njere Ndi
mbewu ya zipatso (kuti imere).
Amatulutsa chamoyo m'chakufa.
Surat 6. Al-An'am Juzu 7
291 V ,>'
n f UiSfi 3j>-»
Ndiponso ngotulutsa chakufa
m'chamoyo. Ameneyu ndi
Mulungu. Nanga
Mukutembenuzidwa chotani?
96. lye ndi Yemwe ali
Wotsekula M'bandakucha, ndipo
amaupanga Usiku kukhala wabata
(nthawi Yopumula) ndi dzuwa ndi
mwezi Kukhala zowerengera
[masiku ndi zaka (Kalendala)].
Ichi nchikonzero cha Wamphamvu
zoposa, Wodziwa kwambiri.
97. lye ndi amene
anakupangirani Nyenyezi kuti
zikutsogolereni (Njira) mum'dima
wapamtunda ndi panyanja. Ndithu
talongosola Mokwanira zizindikiro
(zathu) Kwa anthu odziwa
98. Ndipo lye ndi yemwe
adakulengani Kuchokera mu
mzimu umodzi. (Kwa inu) alipo
malo okhalapo (dziko Lapansi
kapena m'mimba mwa Mayi)
ndiponso posungirapo (Mmanda
kapena munsana mwa bambo)
Ndithu, tafotokoza zizindikiro
(Zathu) kwa anthu ozindikira.
99. lye ndi Yemwe
amavumbwitsa mvula Kuchokera
kumwamba. Ndi madzi a mvulayo
timameretsa Mmera wachinthu
chilichonse. Ndipo m'menemo
Tikuphukitsa masamba obiriwira,
Ndipo mum'mera umenewo
%$m
Siirat 6. Al-An'am Juzu 7
292
V *>i
*\ ^bwVl Ojj~-
tikutulutsa Mkati mwake njere
zosanjikana; Ndiponso m'kanjedza
m'mikoko Mwake (Mumatuluka)
maphava ogoweka (Ndizipatso).
Ndipo amakumeretserani Minda
yampesa, mzitona ndi
Makomamanga, ofanana ndi
osafanana. Tapenyani zipatso zake
pamene Zikupatsa ndi kupsa
kwake. Ndithu, m'zimenezo Muli
zizindikiro Kwa anthu
okhulupirira.
100. Ndipo (pamwamba pa
izi)Anthu ampangira Mulungu
ziwanda Kukhala zinzake,pomwe
lye ndi Yemwe adazilenga.Ndipo
akumnamizira Kuti ali ndi ana
aamuna ndi aakazi Popanda
kudziwa. Ali kutali
Wolemekezekayo,Ndipo
Watukuka kuzimene Akusimbazo.
101. lye ndiye Mlengi
wathambo Ndi nthaka, zingatheke
bwanji Kukhala ndi mwana
pomwe lye alibe mkazi? Ndipo
Ndi Yemwe adalenga chinthu
Chilichonse.Ndiponso lye
Ngodziwa chinthu chilichonse.
102. Ameneyu ndi Mulungu,
Mbuye Wanu; palibe wina woti
nkumpembedza Mwachoonadi
koma lye. Mlengi wachinthu
chilichonse . Choncho,
mpembedzeni. lye ndi Muyang'aniri
wachinthu chilichonse.
4.
Surat 6. Al-An'am Juzu 7
293
v tjA-i
*; fbuSfi Sj>->
103. Maso samufika (kuti
nkumuona); koma lye amawafika
maso (amawaona pamodzi Ndi eni
masowo). lye Ngodziwa Zobisika
kwambiri ndi zoonekera
104. "Ndithu umboni
wotsimikizika Wakufikani
kuchokera kwa Mbuye
Wanu,choncho amene atsekule
maso ake Nkuyang'ana ndiye kuti
Zotsatira zake zabwino zili pa iye
Mwini. Ndipo amene akhale
wakhungu Zili pa iye mwini.
Ndipo ine Sindili kapitawo wanu."
105. Motero tikulongosola
mwatsatanetsatane Zizindikiro,
(kuti azindikire). Ndipo anena
kuti:"Wachita kuphunzira (izi, si
Mulungu amene Wakuuza" Ndipo
tazibwerezabwereza chonchi) Kuti
tilongosole ndi kufotokoza
Momveka kwa anthu odziwa.
106. Tsata zimene Mbuye wako
wakuvumbulutsira. Palibe
Wopembedzedwa mwachoonadi
Koma Iye. Ndipo ape we
Amushirikina.
107. Ndipo Mulungu akadafuna
Sakadamphatikiza (ndi mafano)
Ndipo sitidakuike pa iwo kukhala
Muyang'aniri wawo. Ndipo iwe
suli Muyimiliri wawo.
108. Ndipo usawatukwane
amene akupembedza (Mafano)
C 'l*£ 9 < t »f, '^*\\> 9 <
^I^&u%t2$!i!5£
Surat 6. Al-An'am Juzu 8
294
A tjJrl
1 ^OuSfl Ojj-*»
kusiya Mulungu, kuopera Kuti
angamtukwane Mulungu
mwamwano Popanda kuzindikira.
Motero Tawakometsera anthu onse
zochita Zawo. Potsiriza
adzabwerera Kwa Mbuye wawo,
choncho, lye adzawauza zonse
zomwe Adali kuchita.
109.Ndipo (Akafiri) adalumbira
Mulungu ndi Malumbiro
amphamvu kuti ngati
Adzachikhulupirira. Nena:
"Zozizwitsa Zili kwa Mulungu
(sizili m'manja mwanga). Kodi
nchinthu chanji
chingakudziwitseni (Inu Asilamu)
kuti (ngakhale) chidze
(Chozizwitsacho) iwo
sangakhulupirire?
HO.Ndipo titembenuza Mitima
yawo ndi maso awo (Kotero kuti
sangathe kuchikhulupirira
Ngakhale atachiona
chozizwitsacho) Monga momwe
sadaikhulupirire (Qur'an)
Poyamba ndipo tiwasiya
Akuyumbayumba m'machimo awo.
111. Ndipo ngati
tikadawatumizira Angelo (Kuti
adzaikire umboni za uneneri
Wako), ndipo akufa
nkuwayankhula, (Naonso
nkuvomereza kuti izi Nzoona;
kuonjezera apo)
Nkuwasonkhanitsira chinthu
^i^^aniS
i«Wi
*Wr*"
9'<
Surat 6. Al-An 4 am Juzu 8
295
A *>i
% fUuVl 5jj~»
Chilichonse pamaso pawo,
Sakadakhulupirira pokhapokha
Mulungu akadafuna Koma ambiri
a iwo ngosazindikira.
112.Ndipo nchomwechi
tidamuikira Adani mneneri
aliyense (omwe) Ndi asatana a
muanthu ndi asatana A
m'ziwanda,( omwe)
amadziwitsana Wina ndi mnzake
mawu okometsa Ncholinga
chonyenga.Ndipo Mbuye wako
Akadafuna, sakadatha kuchita
zimenezi Choncho asiye ndi
zimene akupeka
113. Ndi kuti ipendekere
kumawu amenewo Mitima ya
anthu osakhulupirira Tsiku la
chimaliziro, ndi kuyanjana Nawo
(mawu) ndikutinso apeze
(Machimo) omwe amawapeza.
114.(Nena:)"Kodi ndifune
woweruza Wina kusiya Mulungu,
pomwe lye Ndi Yemwe
adavumbulutsa Buku kwa inu
Lofotokoza chilichonse?" Ndipo
Omwe tidawapatsa Buku
Akudziwa kuti (Qur'an)
yavumbulutsidwa Ndi Mbuye
wako mwachoonadi. Choncho,
usakhale mwaokaikira.
115. Ndipo mawu a Mbuye
wako akwanira Moona ndi
mwachilungamo. Palibe Amene
rt'^r^i *w* 9'\$ 9 <C"
Surat 6. Al-An'am Juzu 8
296
A ftji-l
n £ liu^i 5jj-*
angathe kusintha mawu Ake. lye
Ngwakumva, Ngodziwa.
116.Ngati umvera ambiri
amene ali Padziko lapansi,
akusokeretsa Panjira ya Mulungu.
Satsatira Koma zakungoganizira.
Ndipo Sali chilichonse koma
Akungonama
117.Ndithu, Mbuye wako ndi
Yemwe Akudziwa bwino amene
asokera Ku njira Yake, ndiponso
lye Akudziwa bwino za oongoka.
118. Choncho, idyani (nyama)
zomwe Dzina la Mulungu
latchulidwapo (Pozizinga osati zofa
zokha), Ngati inu mukhulupiriradi
aya(zizindikiro) zake.
119.Mungasiirenji kudya
(nyama) imene Poizinga dzina la
Mulungu Latchulidwapo, pomwe
wakufotokozerani Momveka
chomwe wachiletsa Kwa inu,
kupatula (mukadya
choletsedwacho) Mosimidwa ndi
kukakamizidwa (Chifukwa cha
njala)? Koma ndithu ambiri
Akusokeretsa (ena) mwazifuniro
zawo Popanda kudziwa. Ndithu
Mbuye wako ndi Yemwe akudziwa
bwino za Olumpha malire.
120. Siyani machimo oonekera
ndi Obisika. Ndithu, amene achita
Machimo adzalipidwa chifukwa
Cha zomwe adali kuchita (Zoipa).
>"''JLA"
Surat 6. Al-An'am Juzu 8
297
AtjJrl
■\ pbu^Il Sjj~-
121. Ndipo musadye (nyama)
imene Yazingidwa popanda
kutchula Dzina la Mulungu.
Kutero ndikuchimwa. Ndithudi,
asatana amanong'onezera
Abwenzi awo kuti akangane ndi
inu (M'zinthu zonga zimenezi).
Ngati Muwamvera, ndiye kuti
mukhala Amushirikina.
122. Kodi yemwe adali wakufa,
Kenako nkumuukitsa ndi
kumpangira Kuunika; choncho ndi
kuunikako Nkumayenda kwa
anthu, kodi Angafanane ndi
yemwe chikhalidwe Chake chili
mumdima (wa umbuli) Ndipo
sakutha kutuluka m'menemo?
Motero zakometsedwa kwa
Osakhulupirira (zoipa) zomwe
akhala akuchita.
123. Chomwechonso tidaika
mmudzi uli wonse Akuluakulu
owonongamo kuti Azichitamo
ndale (zoletsa anthu Kuyenda pa
njira ya Mulungu). Ndipo ndale
zawo sizipweteka Aliyense koma
iwo eni, koma sazindikira.
124. Ndipo chizindikiro
chikawadzera, Amati:
"Sitikhulupirira, mpaka Tipatsidwe
monga zomwe atumiki A Mulungu
adapatsidwa." Mulungu Ndi amene
akudziwa pamalo pomwe Akuika
uneneri wake, (sikuti
Angapatsidwe munthu aliyense).
Surat 6. Al-An'am Juzu 8 I 298 1 * *j*-i
*\ fbuSfl 5jj^
Posachedwa kunyozeka kochokera
Kwa Mulungu ndi chilango
choopsa Ziwafika amene achita
zoipa Chifukwa chandale zawo
zomwe akhala Akuchita.
125. Choncho, amene Mulungu
akufuna Kumuongola,
amamtsekula chifuwa Chake kuti
Chisilamu chilowemo Ndipo
yemwe Mulungu akufuna
kumulekerera Kusokera
amachichita chifuwa chake
kukhala Chobanika, chovutika
kwambiri (Kutsata Chisilamu)
ngati kuti akukwera Kumwamba.
Umo ndi momwe Mulungu
Akuwaunjikira uve anthu omwe
sakukhulupirira.
126. Ndipo iyi (Chipembedzo
cha Chisilamu) Ndi njira ya
Mulungu yoongoka. Ndithu,
Tazifotokoza zizindikiro momveka
kwa Anthu okumbukira.
127. (Anthu abwino) adzapeza
nyumba Yamtendere kwa Mbuye
wawo. lye Ndi Mtetezi wawo,
chifukwa Cha zomwe adali
kuchita.
128. Ndipo (akumbutse) tsiku
limene Adzawasonkhanitsa onse
(Nkuwauza): "E inu khamu la
ziwanda! Ndithudi, Mudatenga
okutsatirani ambiri mwa anthu
(Powasokoneza)."Ndipo abwenzi
Siirat 6. Al-An'am Juzu 8
299 I A*j*-»
*\ pwty 5jj~*
awo mwa Athu adzati: "Mbuye
wathu! Tidali kupindulitsana.
Pakati pathu Ndipo tsopano
taifikira Nyengo yathu imene
mudatiikira." (Mulungu) adzati:
"Malo anu ndi Kumoto.
Mukakhala m'mmenemo Muyaya,
pokhapokha Mulungu Akafuna."
Ndithu, Mbuye wako Ngwanzeru
zakuya, Ngodziwa kwambiri.
129. Chomwechi timaika
chimvano pakati pawochita zoipa
chifukwa cha machimo omwe
adali kupeza Kuchokera m'zochita
zawo zoipa).
130. (Tsiku la Kiyama
adzafunsidwa): "E inu magulu a
ziwanda ndi anthu! Kodi
sadakudzereni atumiki ochokera
Mwa inu, amene
amakufotokozerani Zizindikiro
zanga, nakuchenjezani Zokumana
ndi tsiku lanu ili?" Adzati :
"Tadziikira umboni tokha." Ndipo
moyo Wadziko lapansi
udawanyenga. Ndipo adzaziikira
Okha umboni kuti iwo Adali
osakhulupirira.
131. Zimenezi nchifukwa choti
Mbuye wako Sali woononga midzi
mwachinyengo pomwe Eni ake ali
oiwala. (Koma ankawatumizira
aneneri Kuti awachenjeze ndi
kuwakumbutsa). l
©'
Mulungu sapereka chilango kwa anthu asanawatumizire Mtumiki. Ndiponso
Surat 6. Al-An'am Juzu 8
300
A *jA-i
*\ pUity i^y*
132. Ndipo onse adzakhala ndi
maudindo (Aulemerero) kuchokera
m'zochita zawo. Ndipo Mbuye
wako sali Wamphwayi pa zimene
akuchita.
133. Ndipo Mbuye wako
Ngokwanira (Wolemera), Mwini
chifiindo. Ngati afuna
Angakuchotseni ndi kuwaika
m'malo Mwanu amene wawafuna
monga momwe Adakulengerani
kuchokera m'mbumba Ya anthu
ena.
134. Ndithu, (palibe chikaiko)
Zomwe mukulonjezedwa, Zifika.
Ndipo simungathe kuzilepheretsa.
135.Nena: "E inu anthu anga!
Chitani Zanu (zimene mufuna)
momwe Mungathere. Nanenso
ndichita zanga. Choncho
mudzaziwa kuti ndani Mapeto ake
adzakhale ndi malo Abwino.
Ndithudi, sangapambane Anthu
ochita zoipa." 1
136. Ampangira Mulungu
(amugawira) gawo M'zomera ndi
ziweto zimene (Mulungu)
sangawalange pa zinthu zomwe nzosatheka kuzizindikira, pokhapokha Mtumiki
atawaphunzitsa, monga kupemphera Swala, kusala pa mwezi wa Ramadhani.
Koma angawalange pazomwe iwo angathe kuzizindikira kuti nzoipa; monga
munthu kumchenjerera mnzake ndi zina zotero.
1 Aya iyi ikusonyeza kuti munthu wapatsidwa ufulu wochita kapena kusachita
poopera kuti angadzanene kuti adakakamizidwa. Apa nzachidziwikire kuti
amene wasankha chabwino adzapeza chabwino. Ndipo yemwe wasankha
choipa adzapeza choipa.
Surat 6. Al-An'am Juzu 8
301
A *jJUi
■\ ^toSh 5jj--
Adalenga. Akunena: "Gawo ili ndi
La Mulungu,"mkuyankhula
kwawo Kwachabe, "Ndipo gawo
ili ndi La aja omwe
tikuwaphatikiza ndi Mulungu."
Choncho zomwe alinga Kuwapatsa
aphatikizi awo, sizingafike Kwa
Mulungu. Ndipo zimene zili Za
Mulungu, ndi zomwe zingafike
Kwa aphatikizi awo (mafano awo):
Kwaipitsitsa kuweruza kwaoku. 1
137. Momwemo milungu
(mafano) yawo Imawakometsera
ophatikiza Mulungu ndi Mafano
kupha ana awo (monga Nsembe ya
mafanowo) kuti awaononge
Ndikuwabweretsera chisokonezo
Pachipembezo chawo. Ndipo ngati
Mulungu Akadafuna, sakadachita
zimenezo. Choncho Asiye ndi izo
zomwe akupeka.
138. Iwo akuti: "Ziweto izi ndi
mbewu izi, Nzoletsedwa; palibe
angazidye koma Amene tawafuna
(kuti adye)" zonsezi Mkuyankhula
kwawo kwachabe. Ndipo
Kale anthu osakhulupirira pamene ankalima akafuna kubzala, minda yawo
adati kuigawa zigawo ziwiri. Ankati "Mbewu zachigawo ichi nza Mulungu, kuti
mbewu zakezo adzazigwiritsa ntchito powapatsa masikini, ana a masiye ndi
osowa. Ndipo ankatinso "Mbewu zachigawo ichi nzamafano athu omwe ankati
ngamnzake a Mulungu kuti zinthu zotuluka m'menemo ziperekedwe kwa
anthu ogwira ntchito m'menemo. Choncho ngati patapezeka mliri pachigawo
chomwe ankati zokolola zake nzamafano awo, amatenga chigawo chomwe
amati dzinthu dzake nza Chauta napereka kumafano. Koma mliri ukagwera
pa chigawo cha Mulungu, sadali kutenga zamafano nkupereka kwa Mulungu.
Izi amachita ngati mafano ngabwino kuposa Mulungu.
Surat 6. Al-An'am Juzu 8
302
A *>l
n f\*jH\ *jj--
(Amanenanso): "Ziweto izi, misana
yake Njoletsedwa (kuikwera)."
Ndipo paziweto zina satchula
dzina la Mulungu pozizinga;-
kungompekera Bodza lye. Ndipo
posachedwa Adzawalipira pa
zomwe adali kupeka.
139. Ndipo amanenanso:
"Zimene zili M'mimba Mwa
ziweto izi, ndi za amuna okha;
Ndipo nzoletsedwa kwa akazi
athu". Koma ngati chili chibudu,
onse Adali kugawana (amuna ndi
akazi). Ndithudi, adzawalipira ndi
zonena zawozo. Ndithu lye
Mulungu),Ngwanzeru zakuya,
Wodziwa kwambiri.
140. Ndithu, adaluza amene
adapha ana awo Mwaumbuli
popanda kudziwa, Ndi kuletsa
(chakudya) chimene Mulungu
awapatsa, pakungompekera Bodza
Mulungu. Ndithu adasokera ndipo
Sadali oongoka.
141. Ndipo Iye( Mulungu) ndi
amene adapanga Minda (ya
mitengo) yothaza Ndi yosathaza;
ndipo (Adapanga) mitengo
yakanjedza ndi Mmera wazipatso
zosiyanasiyana makomedwe Ake
ndipo adapanganso mzitona ndi
Makomamanga, zofanana
(mmaonekedwe) ndi Zosiyana
(mmakomemedwe). Idyani zipatso
zake Pamene zikupatsa. Ndipo
<&'!>* VrtKB't''. »_! .*''*f<'
jp&&&k g$ tx£ $%
"'($' \ 9 h\''' 9 ~'\\<\'i "h
Surat 6. Al-An'am Juzu 8
303 A *>
*\ fbuty «jj->
perekani Chopereka chake tsiku
lokolola (Powapatsa masikini ndi
ogundizana Nawo nyumba). Ndipo
musaziononge Pakudya mopyoza
muyeso. Ndithu, lye (Mulungu)
sakonda opyoza muyeso.
142. Ndipo m'gulu la nyama,
(Mulungu adalenga ) Zonyamulira
katundu ndi zopangira choyala
(Bweya bwake). Idyani zimene
Mulungu wakupatsani ndipo
musatsate Mapazi a Satana (ndi
abwenzi ake Pozichita halali
kapena haramu Zomwe Mulungu
sadalamule. Satana Sakufunirani
zabwino); Ndithu iye Ndi mdani
wanu woonekera.
143. (Adakulengerani) mitundu
isanu Ndi itatu yanyama
(pophatikiza Zazimuna ndi
zazikazi); Nkhosa (adalenga)
ziwiri (Yaimuna ndi yaikazi);
mbuzi (Adalenga) ziwiri (yaimuna
ndi Yaikazi). Nena: "Kodi Iye
Adakuletsani zazimuna zonse
Ziwiri, (mbuzi ndi nkhosa) Kapena
zazikazi ziwiri, (Nkhosa ndi
mbuzi), kapena zomwe Zili
m'mimba mwa zazikazi Ziwirizo?
Ndiuzeni mwanzeru ngati
Mukunenazi nzoona (kuti
Mulungu Adatero).
144. Ndipo (adalenganso)
ngamira ziwiri, (Yaikazi ndi
yaimuna). Ng'ombe
U^$&3*>m£>i
b *"». . CJil ' ' »'\
Surat 6. Al-An'am Juzu 8
304
A *j*-i
1 flAiSll 3jJ-*>
(Adalenganso) ziwiri, (yaimuna
Ndi yaikazi). Nena: "Kodi (lye)
Adakuletsani zazimuna zonse
ziwiri (Ngamira ndi ng'ombe),
kapena zazikazi Zonse ziwiri
(ngamira ndi ng'ombe), Kapena
zomwe zili m'mimba mwa
Zazikazi ziwirizo? Kodi mudali
Mboni pamene Mulungu
ankakulamulani izi? Kodi ndi
ndani woipitsitsa kuposa amene
Akupekera bodza Mulungu kuti
asokeretse Anthu popanda
kudziwa (Malamulo A Mulungu)?.
Ndithu, Mulungu saongola Anthu
ochita zoipa.
145. Nena: "Sindikupeza
m'zimene Zavumbulutsidwa kwa
ine choletsedwa ( kudya) Kwa
yemwe akufuna kudya.
Pokhapokha chikakhala chakufa
chokha, Kapena liwende lomwe
limachucha, Kapena nyama ya
nkhumba; chifukwa Chakuti
zonsezi ndi uve (ndiponso Kudya
zotere) ndiko kutuluka
M'chilamulo cha Mulungu.
Kapena (Nyama) yozingidwa
popanda Kutchulapo dzina la
Mulungu. Koma Amene
wasimidwa (nkudya zoterezi)
Popanda kukonda kapena kupyoza
Malire, ndithu, Mbuye wako
Ngokhululuka Kwambiri,
Ngwachisoni. (Wotere
Amamkhululukira) .
Surat 6. Al-An'am Juzu 8
305
A*>i
*\ fUJ 5 ^ Qjj**
146. (Izi ndi zomwe
takuletsani). Naonso Ayuda
tidawaletsa kudya Nyama iliyonse
yokhala ndi zikhadabu Ndipo
ng'ombe ndi mbuzi tidawaletsa
Kudya mafuta ake kupatula mafuta
Omwe misana yake yasenza,
kapena Okhala m'matumbo,
kapena omwe Asakanikirana ndi
mafupa. Tidawalipira izi chifukwa
cha machimo Awo. Ndithu, Ife
ndioona (pazomwe Tikunenazi).
147.Ngati akukutsutsa
(pazimene Zavumbulutsidwa),
auze (Mowachenjeza): "Mbuye
wanu (Yemwe ngofunika
kum'khulupirira Ndi kutsatira
malamulo ake), Ngwachifundo
chambiri (kwa yemwe
Akumumvera, ndi yemwe
akumunyoza Pano padziko
lapansi). Komatu Chilango chake
sichibwezedwa Kwa anthu oipa."
148. Amene akuphatikiza
(Mulungu ndi Mafano) anena:
"Ngati Mulungu Akadafuna,
sitikadam'phatikiza, Ife ngakhale
makolo athu. Ndipo Sitikadaletsa
chilichonse. (Choncho, Izi zomwe
tikuchita, Mulungu Akuziyanja).
Momwemonso adatsutsa Omwe
adalipo patsogolo pawo Kufikira
adalawa chilango chathu. Nena:
"Kodi muli nako kudziwa (koku-
Tsimikizirani zimenezi)? Koti
Surat 6. Al-An'am Juzu 8
306
A*j*-l
n fW*iii 3jj--
mungatitulutsire. (Umboni wake
wotsimikizira kuti Mulungu
Adakulamulani zimenezi)? Inu
simutsatira China, koma
zongoganizira basi. Ndipo
Simukunena china koma zabodza
basi."
149.Nena: "Mulungu ndi
Yemwe ali ndi Umboni
wokwanira.Choncho akadafuna,
Akadakuongolani nonsenu."
ISO.Nena: "Tabweretsani
mboni zanuzo Zomwe zingapereke
umboni kuti Mulungu adaletsa izi.
Ndipo ngati Zitapereka umboni,
(mboni zawozo) usaikire Nawo
umboni pamodzi Ndi iwo. Ndipo
usatsate zofuna Za omwe atsutsa
zizindikiro zathu Ndi amene
sakhulupirira tsiku Lomaliza;
omwenso akufanizira Mbuye
wawo ndi milungu yabodza.
lSl.Nena: "Idzani kuno,
ndikuwerengereni Zomwe Mbuye
wanu wakuletsani."
Musamphatikize Ndi chilichonse,
ndipo achitireni Zabwino makolo
anu; musaphe ana Anu chifukwa
chakuopa umphawi; Ife tikupatsani
riziki inu pamodzi Ndi iwo;
musayandikire Zoyipa, zoonekera
ndi zobisika; ndipo Musaphe
munthu yemwe Mulungu adaletsa
(Kumupha) kupatula ikapezeka
Surat 6. AI-An'am Juzu 8
307
A*>i
% pUiSf* *jj~»
njira Yoyenereza (kumupha).
Akukulangizani Izi kuti muziike
mu nzeru zanu.
152.Ndipo musachiyandikire
chuma cha Ana amasiye, koma
m'njira yabwino (Monga
kuchichulukitsa ndi malonda)
Mpaka afike pamsinkhu
wokwanira. Ndipo kwaniritsani
mwachilungamo Miyeso yambale
ndi masikelo; Sitikakamiza
munthu koma chimene Angathe;
ndipo pamene mukunena,
(popereka Umboni), nenani
mwachilungamo ngakhale
(Umboniwo) uli wokhudza
achibale. Ndipo kwaniritsani
lonjezo la Mulungu. Izi ndi zomwe
akukulangizani Kuti
mukumbukire.
153. (Auze kuti) ndithu, iyi ndi
njira yanga Yoongoka. Choncho
itsateni. Ndipo musatsate Njira zina
zambiri kuopera kuti Zingakuikeni
kutali ndi njira Yake, (Mulungu)
wakulangizani izi kuti Mudziteteze
kuzoipa.
154. Ndipo Musa tidampatsa
Buku (kukhala) Lokwaniritsa
(chisomo) kwa yemwe Wachita
zabwino, lofotokoza chinthu
Chilichonse, chiongoko ndi
Chifundo, kuti iwo akhulupirire Za
kukumana ndi Mbuye wawo.
J» i^ • 9 <r
t "Z 'J > -'"fey 9 >'\'\
Surat 6. Al-An'am Juzu 8
308
A *>i
T, ^UiSfl 3j_^j
155.Ndipo iyi (Qur'an) ndi
Buku lodalitsika Lomwe
talivumbulutsa (kwa inu),
Choncho, litsateni ndi kuopa
(Mulungu) kuti muchitiridwe
Chifundo;
156. Kuti musadzanene (tsiku la
Kiyama) Kuti: "Mabuku
adavumbulutsidwa Pamagulu awiri
omwe adalipo Patsogolo pathu,
(Ayuda ndi Akhrisitu); ndipo ife
sitidadziwe Chilichonse pazomwe
adali kuwerenga Ndi kuphunzira;"
157. Kapena kuti musadzati:
"Likadavumbulutsidwa Buku kwa
ife, ndithudi, Tikadakhala oongoka
kuposa iwo." Choncho,
chakudzerani chizindikiro
Kuchokera kwa Mbuye wanu, ndi
Chiongoko ndi mtendere. Kodi
Ndani woipitsitsa kwambiri
kuposa Amene watsutsa
zizindikiro za Mulungu ndi
kutembenukira kutali Nazo?
Tidzawalipira amene
akutembenukira kutali ndi
zizindikiro zathu, Chilango choipa,
chifukwa chakudziika Kwawo
kutali.
158. Kodi chilipo chimene
akudikira Kuposa kuwadzera
angelo (Kudzawachotsa miyoyo
yawo?) Kapena kudza Mbuye
Wako?(Tsiku la Kiyama
kuzaweruza) Kapena kudza zina
^ssyauJi; 4 *'
-»i.n * . ."
\j>€t*}»
«Vx s^J
Ooo^j fid c^j yVuo (^j
Surat 6. AI-An'am Juzu 8
309
A *>l
1 f\*j^\ Qjj~>
mwa Zizindikiro za Mbuye wako
(zomwe Adati zidzadza)? Tsiku
lakudza Zina mwazizindikiro za
Mbuye wako, Munthu
(wosakhulupirira) Chikhulupiriro
chake (panthawiyo)
Sichidzamthandiza, yemwe
sadakhulupirirepo kale, kapena
(Msilamu) Yemwe sanapindule
nacho Chikhulupiriro chake. Nena:
" Dikirani. Nafenso tikudikira." 1
159.Ndithudi, anthu amene
achigawa Chipembedzo chawo,
nakhala Mipingomipingo, iwe
Siuli nawo pachilichonse. Ndithu,
zotsatira zawo zili kwa Mulungu,
(ndi yemwe adzawalanga. Ndipo
panthawi yowalanga) adzawauza
Zomwe adali kuchita.
160. Amene wachita chabwino
alipidwa Zabwino khumi zofanana
ndi icho. Ndipo amene wachita
choipa adzalipidwa koma chonga
icho (Popanda kuonjezera). Ndipo
Iwo sadzaponderezedwa. 2
%?&%$¥'* ^">'
■la*
%m^
1 Chisilamu kuti chikamthandize munthu nkofunika kuti achigwiritsire ntchito
pamoyo wake wonse. Chisilamu chokha popanda kuchigwiritsira ntchito
sichikwanira ndiponso sichingamtchinjirize munthu kuchilango chamoto.
Ndipo yemwe sali Msilamu kuti Chisilamu chikamthandize nkofunika kuti
alowe m'Chisilamu ali ndi moyo, osati pamene imfa yamufika. Ndipo nayenso
Msilamu wochita zoipa, akalapa imfa itamufika kale kulapa kwakeko
sikungamthandize. Koma alape pamene ali ndi moyo wangwiro. Pamenepo
ndiye kuti Mulungu alandira kulapa kwake. Osati kulapa uku imfa akuiona ndi
maso ake.
2 China mwachifundo cha Mulungu pa zolengedwa zake ndiko kuti
adzamulipira munthu patsiku la chimalidziro mosiyanitsa pakati pa chabwino
ndi choipa. Ngati adachita chabwino chimodzi, adzamulipira mphoto ya zinthu
Surat 6. Al-An'am Juzu 8
310
A *>l
1 fUjSfi Oj^-O
161.Nena: "Ndithudi, ine
Mbuye Wanga wandiongolera
kunjira Yoongoka, kuchipembedzo
cholingana, Chomwe ndi
chipembedzo cha Ibrahim, Yemwe
adali wolungama. Sadali
Mwaophatikiza (Mulungu ndi
mafano).
162.Nena: "Ndithudi, Swala
yanga, Mapemphero anga onse,
moyo wanga, Ndi imfa yanga,
(zonse) nza Mulungu, Mbuye
wazolengedwa zonse:
163. lye alibe wothandizana
naye. Izi ndi zomwe
ndalamulidwa, Ndipo ine ndine
woyamba mwaogonjera."
164.Nena: "Kodi ndifune
mbuye wina Kusiya Mulungu,
pomwe lye ndi Mbuye Wachinthu
chilichonse? Ndipo Mzimu
uliwonse siuchita choipa Koma
ukudzichitira wokha. Mzimu
wosenza machimo siudzasenza
Machimo a mzimu wina. Kenako
Kobwerera kwanu (nonse) ndi kwa
Mbuye wanu, (Mulungu), ndipo
Adzakuuzani zomwe mudali
kusiyana."
165. Ndipo lye ndi Yemwe
wakuchitani kukhala A
®jf»o&te6^
khumi zoposera pachabwino ndipo ngati adachita choipa, sadzamuonjezera
malipiro achoipacho koma adzamulipira chofanana ndi choipacho. Tanthauzo
lake nkuti chabwino chimodzi malipiro ake ndi zabwino khumi; pomwe choipa
chimodzi mphoto yake ndi choipanso chimodzi.
Surat 6. Al-An'am Juzu 8
311
A *>1
*\ pUity 5jJm»
m'lowam'malo padziko (kulowa
M'malo mwa anzanu omwe
adaonongeka). Ndipo wawatukula
paulemerero (ndi Pachuma) ena a
inu pamwamba pa ena Kuti
akuyeseni pazomwe wakupatsani.
(Amene apatsidwa chuma ndi
ulemerero, Athandize amene
sadapatsidwe. Ndipo Amene
sadapatsidwe, apirire asalande
Chinthu chamwini). Ndithudi,
Mbuye Wako ngwachangu
pokhaulitsa. Ndiponso lye
Ngokhululuka kwabasi
Ngwachisoni. 1
Ndime iyi ikusonyeza kuti kukhupuka ndi ulemerero, sindizo zizindikiro
zosonyeza kuti munthuyo ngofunika kwa Mulungu. Ndiponso kusauka ndi
kunyozeka sizizindikiro kuti munthuyo ngosafunika kwa Mulungu kapena
wonyozeka kwa Chauta. Koma kulemera, ulemerero, kusauka ndi
kunyozeka.zonsezi amazipereka m'njira yamayeso.
Surat 7.
Al-A'raf Juzu 8
312
AtjA-i
V iJljpty «jj-.
1
SURAT AL-A'RAF VII
Sura iyi idavumbulutsidwa ku Makka kupatula Aya 163
kufikira 170. Koyambirira kwa Sura iyi ikupitiriza mawu a
m' Surat Al - Imran. Pambuyo pake yasonkhanitsa mawu
achiyambi chakulengedwa kwa munthu. Yafotokoza nkhani ya
kulengedwa kwa Adamu ndi Hawa, ndikutuluka kwa awiriwa
m'munda wamtendere, kupyolera m'manong'onong'o achinyengo
a Satana. Yafotokozanso kuti manong'onong'o onyenga a
Satana akupitirira ku anthu kudzera kumbali ya chovala ndi
chakudya.
Yafotokozanso surayi kuti anthu alingalire zolengedwa za
Mulungu kumwamba ndi pansi monga momwe zilili Sura za ku
Makka.
Yafotokozanso nkhani za aneneri a Mulungu monga: Nuhi,
Hudi ndi anthu ake (Adi). Kenako nkhani ya Swaleh ndi anthu
ake (Asamudu), omwe ankadziwika ndi mphamvu ndi chuma.
Yakambanso nkhani ya Luti pamodzi ndi anthu ake omwe
ankachita za uve, ndi nkhani ya Shuaibu pamodzi ndi anthu a ku
Midiyani. Surayi yasonkhanitsa nkhani zoona zomwe zili ndi
malango ndi maphunziro m'kati mwake. Ndipo Mulungu
Woyera wafotokozanso nkhani ya Musa pamodzi ndi Farawo ndi
zomwe Farawo ndi anthu ake adapeza. Surayi yamaliza pofotokoza
za yemwe wapatsidwa chiwongoko, kenako ndikudzichotsa
m'chiwongokocho posokonezedwa ndi Satana ndi zomwe
zingamtsatire pakutero. Kenako yafotokoza ulaliki wachoonadi
omwe udadza ndi Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale
ndi iye).
Surat7. AI-A'raf Juzu 8
313 A *>»
V J>\j*H\ 3jj--
SuratAl-A'rafVII
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni.
1. Alif-Lam-Mim-Sdd.
2. (Iyi Qur'an ndi) Buku
(lopatulika) Lomwe
lavumbulutsidwa kwa iwe.
Choncho chifuwa chako
chisabanike Ndi ilo (poopa
kufikitsa mawu ake Kwa anthu
kuti angakuyese wabodza;) Kuti
uwachenjeze Nalo (otsutsa) ndi
kuti likhale Chikumbutso kwa
okhulupirira (kuti Aonjezere
chikhulupiriro chawo). 1
3. Tsatirani zomwe
zavumbulutsidwa kwa Inu
kuchokera kwa Mbuye wanu,
ndipo Musawatsatire omwe sali
Mulungu Powayesa atetezi (anu).
Ndi zochepa zimene
Mumazikumbukira.
4. Ndi midzi yambiri imene
tidaiononga ndipo Chilango chathu
chidaidzera Nthawi yausiku,
kapena usana iwo Atagona tulo
tamasana, (akupumula Monga
momwe zinawachitikira Anthu a
Loti ndi anthu a Shuaibu).
*.
O^I^JMkU-
i c^
1 ^^Ti
Wy«S7"J»
1 Apa akumuuza Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) kuti asaope
kulengeza zimene Mulungu wamuululira. Asatekeseke ndi otsutsa ngakhale
atachuluka (bwanji) chotani. Mlaliki aliyense akuuzidwanso chimodzimodzi.
Anene choonadi kwa anthu ndipo asaope kudzudzulidwa
Siirat 7. Al-A'raf Juzu 8 I 314 I A *>i
V tJljP^I 3j>-
5. Ndipo sikunali Kulira kwawo
pamene Chinawafika chilango
chathu koma Kunena (ndi
kuvomereza): "Ndithudi, Ife tinali
ochita zoipa." (Koma Kuvomereza
kwawoko Sikunawapindulire
kanthu).
6. Mtheradi tidzawafunsa
(anthu) amene Anatumiziridwa
(Atumiki) Naonso atumikiwo
Tidzawafunsa.
7. Tsono tidzawauza
mozindikira bwino-bwino
(chilichonse chimene ankachita).
Ndipo sitidali kutali (nawo Pamene
ankachita zochita zawo).
8. Ndipo sikero (yoyezera
zochita za Anthu) tsiku limenelo
idzakhala Yoona (yopanda
chinyengo). Choncho, Amene
idzalemere miyeso yake
(Yazabwino), iwowo ndiwo
opambana.
9. Ndipo amene idzapepuke
miyeso Yawo (yazinthu zawo
zabwino), Iwo ndi amene ataya
pachabe moyo Wawo chifukwa
chakuzichitira Zosalungama
zizindikiro zathu.
10. Ndithudi tinakupatsani
mphamvu Yokhalira padziko,
ndipo Takupangirani m'menemo
Zinthu zofunika pamoyo Wanu.
Koma kuyamika Kwanu mpang'ono.
0i
Siirat7. Al-A'raf
Juzu 8
315
A frjfci
V JMy^l ijy*
ll.Ndithudi, tinakulengani,
kenako Tidakukonzani
(pokupatsani ziwalo) Ndi kunena
kwa Angelo kuti: "Mgwadireni
Adamu." Ndipo adamgwadira
Kupatula Iblis, sadali mwa
ogwada.
12. (Mulungu) anati: "Nchiyani
chakuletsa Kumgwadira pamene
ndakulamula?"(Satana) anati: "Ine
ndine wabwino Kuposa iye. Ine
munandilenga ndi Moto koma iye
mudamulengaNdi dongo."
13. (Mulungu) adati: "Choncho,
choka M'menemo ndi kutsikira
pansi. Sikofunika kwa iwe
kudzitama M'menemo. Tuluka,
ndithu, iwe Ndiwe mmodzi wa
onyozeka." 1
14. (Satana) anati: "Ndipatseni
Nthawi mpaka tsiku Limene
adzaukitsidwa (Akapolo anu ku
imfa)."
15. (Mulungu) Adati: "Ndithudi
iwe ndi mmodzi Wa opatsidwa
nthawi."
16. Iye (chifukwa cha njiru yake
yoopsa Pa Adamu) adati: "Tsono
chifukwa Chakuti mwandichita ine
kukhala Wopotoka,
ndidzawakhalira (akapolo Anu
«ssaK(Jitsjw*
Mulungu anamtulutsa m'nyumba ya
chakudzitama ndi kunyoza tamulo la Mulungu.
ulemerero Wake chifukwa
Surat7. AI-A'raf
Juzu 8
316
A t >i
V iJljpty 6jf
ndikuwabisalira) panjira yanu
Yoongoka (ndi cholinga
chowasokeretsa)".
17. Kenako ndidzawadzera
(mbali ya) Kutsogolo kwawo,
m'mbuyo mwawo; Kumbali
yakumanja kwawo ndi kumanzere
Kwawo, mwakuti simudzapeza
ambiri A iwo oyamika.
18. (Mulungu) anati: "Tuluka
m'menemo, Uli wonyozeka ndi
wothamangitsidwa. Amene
adzakutsata iwe mwa iwo,
Ndithudi, (ndikamponya kumoto).
Ndipo ndikaidzadzitsa Jahannama
ndi Inu nonse."
19. (Kenako Mulungu adanena
kwa Adamu) "E iwe Adamu!
Khala ndi mkazi wako M'munda
wa Mtendere, (sangalalani ndi
Zomwe zili m'menemo) idyani
Paliponse pamene mwafuna. Koma
mtego Uwu musawuyandikire
kuopera kuti Mungakhale m'gulu
la odzichitira okha zoipa."
20. Satana adayamba
kuwanong'oneza (Zoipa) kuti
chioneke kwa iwo Chimene
chinabisika kwa iwo monga
Umaliseche wawo. Ndipo (Satana)
Adati: "Mbuye wanu sadakuletseni
Mtengo uwu, koma pachifukwa
chakuti Mungasanduke angelo
awiri, kapena Kuti mungakhale
amuyaya."
9 ''9 *\< * '*J> 9 'i 9<9w9J£'M4.
Q&fyvt
Surat7. Al-A'raf Juzu 8
317
A *jJM
V tJt^ty 5j>-
21. lye adaalumbirira onse awiri
kuti: "Ndithudi, ine ndine Mmodzi
mwa olangiza (Ndikukufunirani
zabwino)."
22. Adawakopa mwachinyengo.
Ndipo Pamene adalawa zipatso za
mtengowo Umaliseche wawo
udaoneka kwa iwo Nayamba
kudziphatika Masamba (a
mitengo) a m'mundamo. Ndipo
Mbuye wawo adawaitana
(Mowadzudzula nati:) "Kodi
sindinakuletseni Mtengowu ndi
kukuuzani kuti Satana ndi mdani
wanu woonekeratu?"
23. Iwo (Adamu ndi mkazi
wake) adati: (Modzichepetsa),
"Tadzichitira Tokha zoipa, E Mbuye
wathu! Ngati Simutikhululukira
ndi kuchita nafe Chifundo ndiye
kuti tikhala mwa otaika."
24. (Mulungu) adati: "Tsikani
pansi uku Pali chidani pakati panu.
Ndipo Padziko lapansi ndi pokhala
panu Ndi kusangalala kwanu
mpaka m'nthawi Yoikidwayo".
25. (Mulungu) adatinso:
"Muzikakhala moyo pamenepo,
Ndipo muzikafa Pamenepo; ndipo
Momwemo mudzatulutsidwa
(Mutauka kwa akufa)."
26. (Mulungu adati kwa ana
onse a Adamu): E inu ana a Adam!
Ndithu tatsitsa kwa inu Chovala
&2ft^<i$$ ®^l
©I
s*
Siirat7. Al-A'raf
Juzu 8
318
A *>!
V cily^l 5jj--
chobisa umaliseche wanu ndi
Chodzikongoletsera nacho. Koma
Chovala choopa nacho Mulungu
(Pakudziyeretsa ku zoletsedwa)
Chimenecho ndicho chabwino
koposa. Zimenezo ndi zizindikiro
Za (chisomo cha) Mulungu Kuti
iwo akumbukire.
27. E inu ana a Adam! Satana
Asakusokonezeni monga momwe
Adawatulutsira makolo anu
M'Munda wamtendere ndi
kuwavula Onse awiri chovala
chawo kuti Awasonyeze
umaliseche wawo. Ndithu, iye ndi
mtundu Wake akukuonani pomwe
inu Simukuwaona. Ndithu,
asatanaTawachita kukhala abwenzi
a Osakhulupirira.
28. Ndipo (osakhulupirira)
akachita Chauve amanena: "(I c hi)
tidawapeza Nacho makolo athu
(akuchichita) Ndiponso Mulungu
watilamula Chimenechi." Nena:
"Ndithu Mulungu Salamula
zonyasa. Kodi mukumunenera
Mulungu zomwe simukuzidziwa?"
29. Nena: "Mbuye wanga
walamula Chilungamo; ndiponso
(wandiuza Kuti ndikuuzeni kuti)
*&$&$2fr4)&$g.
? 9* 9 ifoC "9 9 9 S i 'L fify\ v
9^' 9? 9l99 9*<**f ,ft 9»*"< 9 I
Mulungu akutiuza kuti tivale nsalu zomwe Mulungu adatipangira kuti
zikongoletse matupi athu. Komatu akutilamulanso kuti tivale nsalu
zokongoletsa mitima yathu; nsalu yomwe njotsatira nayo malamulo a Mulungu
ndi kuletsa zomwe lye waletsa; ndi kuchita zokhazo zomwe Mulungu
walamula. Nsalu imeneyi ndi "takuwa" (kuopa Chauta). Sibwino kukongoletsa
kunja kwa thupi kokha pomwe mumtima mwadzadza zauve.
Surat 7. Al-A'raf Juzu 8
319
A ftj*-i
V cJiy^i Sjj-
lungamitsani Nkhope zanu (kwa
lye) m'nthawi ya swala iliyonse,
ndipo mpembedzeni lye yekha
momuyeretsera chipembedzo
Monga lye adakulengani
pachiyambi, Momwemonso
mudzabwerera kwa lye."
30. Gulu Una
waliongola,pomwe gulu Lina
patsimikizika pa ilo kusokera
Chifukwa chakuti iwo adasankha
Asatana kukhala atetezi awo
Kusiya Mulungu; ndipo akuganiza
Kuti iwo ngoongoka.
31. E inu ana a Adamu !
Tengani (valani) Zovala zanu
zabwino pamene
Mukukapemphera Swala iliyonse
ndipo Idyani ndi kumwa; koma
Musapyoze muyeso. lye
(Mulungu) sakonda opyoza
muyeso (Oononga).
32. Nena: "Ndani waletsa
zokongoletsa Za Mulungu,
(zovala), zomwe lye (Mulungu)
adawatulutsira akapolo ake ndi
Zakudya zabwino?" Nena: "Zinthu
zimenezo nzololedwa Kwa amene
akhulupirira (Asilamu) Pamoyo
wapadziko lapansi. (Zidzakhala)
zawozawo tsiku la Chimaliziro.
M'menemo ndi mom we
Tikulongosolera aya Zathu kwa
Anthu ozindikira."
^&$WT>&Q
©,
1 Padali anthu ena omwe adali ndi chikhulupiriro choti kuvala nsanza ndi
Surat7. Al-A'raf
Juzu 8
320 1 A *>»
V cil^l Sj^
33. Nena (kwa iwo): "Ndithu
Mbuye wangaWaletsa zinthu
zauve zoonekera ndi zobisika, Ndi
machimo, ndi kuwukira
(atsogoleri) Popanda choonadi, ndi
kumphatikiza Mulungu ndi
chomwe sadachitsitsire Umboni
(wakuti chiphatikizidwe ndi lye);
ndiponso (waletsa) kumunenera
Mulungu zimene simukuzidziwa. l
34. Anthu onse ali ndi nthawi
yawo Yawo (yofera). Ndipo
nthawi yawo Ikadza sangachedwe
Ngakhale ola limodzi, ndiponso
Sangaitsogolere.
35. E inu ana a Adam!
AkakudzeraniAtumiki ochokera
mwainu namakuuzani
Zivumbulutso zanga,(avomereni)
choncho Omwe adzitchinjiriza
kuzoletsedwa ndi kuchita
Zabwino, sipadzakhala mantha pa
Iwo ndiponso sadzadandaula.
36. Ndipo amene atsutsa
zivumbulutso Zathu
nadzitukumula nazo, awo Ndi
anthu akumoto adzakhala
Mmenemo muyaya.
37. Kodi ndani woipitsitsa
koposa Kuposa munthu wopekera
W&&i&<&0&
kudya zinthu zosakoma ndiko kumuopa Mulungu. Mpaka masiku ano alipobe
anthu oganiza motere. Ndipo nchifukwa chake Mulungu akuvumbulutsa aya
izi kuti kutero sindiko kumuopa Mulungu.
1 Choipa nchoipa basi. Kaya kuchichita moonekera kapena mobisa,
nchoipabe.
Surat7. AI-A'raf Juzu 8
321
A ftjJt-l
V <3ljPty Sj^W
bodza Mulungu kapena wotsutsa
zivumbulutso zake? Iwo gawo
(lachakudya Chimene)
adawalembera liwafika (Pano
padziko lapansi ngakhale Kuti
ngosakhulupirira mwa Mulungu)
Kufikira pomwe adzawadzera
atumiki Athu (Angelo kudzatenga
miyoyo yawo) Nawapatsadi imfa
uku akunena: "Kodi zili kuti zija
munkazipembedza Kusiya
Mulungu?" Adzati: "Zatisowa".
Ndipo adzadzichitira okha umboni
kuti iwo adali Okana Mulungu.
38. (Mulungu) adzati (pa tsiku
lachiweruzo): "Lowani kumoto
pamodzi ndi mibadwo Imene
idamuka kale (inu musanabwere)
Yochokera mziwanda ndi mu
anthu. M'badwo uliwonse pamene
uzikalowa, Udzatemberera unzake
kufikira Pamene onse
adzasonkhana m'menemo.
Adzanena apambuyo kwa
oyambirira Awo: "Mbuye wathu!
Awa, adatisokeretsa. Apatseni
chilango chamoto Chochuluka."
(Mulungu) adzanena: "Aliyense
mwa inu akhala ndi chilango
Chochuluka; koma izi inu
simukudziwa. 1
9} 9 k
Aliyense adzapeza chilango chachikulu. Ndipo awo amene adasokerezedwa:
a) Adzapeza chilango chifukwa cholola kusokerezedwa pomwe adapatsidwa
nzeru zowazindikiritsa zabwino ndi zoipa.
b) Adzapeza chilango chifukwa chochita machimowo.
Surat7. Al-A'raf Juzu 8
322 1 A *>* v ±i\jfiH\ 5j>*
39. Ndipo oyamba adzati kwa
otsiriza: "Inunso mudalibe ubwino
woposa Ife; choncho , lawani
chilango Cha zomwe mudapeza
(m'zochitachita Zanu)."
40. Ndithudi, amene akutsutsa
zivumbulutso Zathu
nadzitukumula nazo (pakukana
Kuzitsata), sadzatsekulidwa kwa
iwo makomo Akumwamba, ndipo
sadzalowa kumunda Wamtendere
mpaka ngamira idzalowe Pa
chibowo cha singano. Umo
ndimomwe Timawalipirira anthu
ochimwa.
41. Moto wa Jahannama
(Gahena) ndi mphasa Yawo;
ndipo pamwamba pawo Adzakhala
ndi (chofunda chamoto)
Chowaphimba. Umo ndimomwe
Tikuwalipirira anthu osalungama.
42. Ndipo amene akhulupirira
ndikumachita Zabwino,
sitikakamiza munthu aliyense
Koma chimene angachithe, awo
ndiwo Anthu a kumunda
wamtendere. M'menemo Iwo
akakhala muyaya.
Tsono amene adali kusokereza anzawo:
a) Adzapeza chilango chifukwa chakuchita kwawo machimo.
b) Adzapeza chilango chifukwa chakuwasokeretsa anthu omwe adawasokeretsa
c) Adzapeza chilango chifukwa chakuyambitsa machimowo
d) Adzapeza chilango chifukwa chowasiira anzawo odza m'mbuyo mwawo
machimo powatsanzira iwo.
Siirat7. Al-A'raf Juzu 8
323
A ftji-l
V cjly^l dj^
43. Ndipo tidzachotsa
kusakondana (komwe Kudali)
m'mitima mwawo; (adzakhala
Okondana ngakhale padziko
lapansi Adali odana) uku pansi ndi
Patsogolo pawo mitsinje
ikuyenda; Ndipo adzanena
(m'kuthokoza kwawo):
"Kuyamikidwa konse nkwa
Mulungu, Yemwe adatitsogolera
ku ichi (chomwe Chatidzetsera
mtendere): Sitikadaongoka
pakadapanda Mulungu Kutiongola.
Atumiki a Mbuye wathu Adadza
ndi choonadi." Ndipo
Adzaitanidwa (ndi kuuzidwa kuti):
"Uwu ndi Munda wa Mtendere
umene Mwapatsidwa chifukwa
cha zomwe Mudali kuchita".
44. Anthu akumunda
wamtendere Adzaitana anthu aku
moto (adzanena Kuti): "Ndithudi
ife tapeza zimene Mbuye wathu
adatilonjeza kuti nzoona. Kodi
nanunso mwapeza zomwe Mbuye
wanu adakulonjezani kuti
nzoona?" (Anthu akumoto)
adzanena: "Inde;" choncho
Wolengeza pakati pawo
azalengeza Kuti "Matemberero a
Mulungu Ali pa anthu ochita
zoipa." 1
1 Mtunda umene ukakhale pakati pa kumoto ndi kumunda wamtendere
ngwautali kwabasi ndipo palibe angauganizire kuti uli mwakutimwakuti. Koma
ngakhale zili chonchi, anthu a kumunda wamtendere adzatha kuyankhulana
Siirat7. Al-A'raf
Juzu 8
324
A ftj*-i
V Jl^l ojj--
45. "Omwe ankaletsa anthu
kuyenda pa Njira ya Mulungu
nafuna kuikhotetsa Njirayo (kuti
ioneke Yokhota pamaso pa anthu),
Omwenso sadakhulupirire za tsiku
Lomaliza."
46. Ndipo pakati pawo (pa
anthu Akumunda wamtendere ndi
akumoto) Padzakhala chotchinga.
Ndipo Pamwamba pachikweza
padzakhala Anthu ena (ofanana
ntchito zawo zabwino Ndi zoyipa)
omwe akazindikira onse (A ku
Janna ndi kumoto), ndi Zizindikiro
zawo. Ndipo akawaitana Anthu a
ku Janna (kuti): "Salaamun
Alayikum (Mtendere ukhale
painu)": Koma asanailowe uku ali
ndi chikhulupiriro (Kuti ailowa).
47. Ndipo maso awo
akakatembenuzidwa (Kuyang'ana)
kumbali ya anthu Akumoto,
adzanena: "Mbuye wathu
Musatiike pamodzi ndi anthu ochita
Zoipa. (Tikhululukireni zolakwa
Zathu. Tilowetseni ku Janna)."
48. Ndipo anthu aja
apachikweza Adzaitana anthu
m^^ss^^
nawo anthu akumoto. Naonso akumoto adzatha kuyankhulana nawo a
kumunda wamtendere. Pamene wailesi za kanema (TV) zisanayambike, anthu
amene sadali Asilamu (anthu osakhulupirira) amati mawu amenewa ngopanda
pake. Amati zidzatheka bwanji anthu okhalirana kutali kumayankhulana ndi
kuonana? Koma Asilamu enieni adali kukhulupirira poti wonenayo ndi
Mulungu. Koma makono nzeru za anthu zatulukira njira zolankhulirana ndi
munthu yemwe ali kutali, ngakhale kumuona kumene, monga pa TV, wailesi
lamya (telefoni) ndi internet.
Surat7. Al-A'raf Juzu 8
325 A *>»
V JMy^i oj^
(akumoto). Adzawadziwa ndi
zizindikiro zawo, Nati:
"Sikudakuthandizeni Kuchuluka
kwanu kuja, ngakhale Zija mudali
kudzitama nazo.
49. "Kodi awa siaja
munkawalumbirira Kuti Mulungu
sangawaninkhe Chifundo?
(Taonani tsopano, Auzidwa kuti):
"Lowani ku Janna. Palibe mantha
pa Inu 5 ndiponso simudandaula."
50. Naonso anthu akumoto
adzaitana A ku Janna (ndikuwauza
kuti): "Tatipungulirani madzi
kapena Chinthu chimene Mulungu
wakupatsani." (Anthu a ku Janna)
adzanena kuti:"Ndithu Mulungu
waletsa kupereka zonse Ziwirizo
kwa osakhulupirira".
51. Omwe adachita
chipembedzo chawo kukhala,
Zinthu zopanda pake ndiponso
Masewero; ndipo udawanyenga
moyo Wam'dziko. Choncho, lero
Ifenso Tiwaiwala (tiwaleka
kumoto) monga Momwe
adakuiwalira kukumana ndi Tsiku
lawo ili, ndi chifukwa Chakukana
kwawo zivumbulutso zathu.
52.Ndithudi, tawabweretsera
Buku lomwe Talifotokoza
mwanzeru, lomwe ndi Chiongoko
ndi chifundo kwa anthu Okhulupirira.
53. Kodi chiliponso chomwe
akudikirira Osati zotsatira zake (za
&>'*"&
^J&SQ&J
Surat7. Al-A'raf Juzu 8
326 I A*>)
V <J\j*H\ «j>-
Bukulo)? Ndipo tsiku lakudza
zotsatira Zake, adzanena amene
kale sadalilabadire: "Ha! Atumiki
a Mbuye Wathu adadzadi ndi
choonadi. (Tsopano tikuvomereza)
. Kodi Tingakhale nawo ife
aomboli oti Atiombole (kwa Mbuye
wathu)? Kapena tingabwezedwe
kuti tikachite (Zabwino) osati zija
tinkachita?" Zoonadi adziononga
okha, ndipo Zawasowa zabodza
zomwe adali kupeka.
54. Ndithudi, Mbuye wanu ndi
Mulungu Yemwe adalenga
thambo ndi nthaka M'masiku
asanu ndi limodzi. Kenako
adakhazikika Pampando wake
wachifumu. Amauchita usiku kuti
uvindikire Usana, zimatsatana
mwamsangamsanga. Ndipo dzuwa
ndi mwezi ndi nyenyezi
Nzofewetsedwa, (zikuyenda
mogonjera) ndi Lamulo Lake.
Dziwani kuti kulenga Nkwake,
ndiponso kulamula nkwake.
Ndithudi, watukuka Mulungu
Mbuye Wazolengedwa (zonse).
55. Mpempheni Mbuye wanu
Modzichepetsa ndi
Mwakachetechete (mosakuwa) lye
(Mulungu) sakonda Opyola malire. 1
*9t>' m '\9l\4X*> 39*'
Zopempha zathu tikamampempha Mulungu tikuuzidwa kuti tizipempha
modzichepetsa ndi mopanda phokoso. Tisamachite phokoso pamene
tikupempha "maduwa" monga zikuchitikira m'misikiti yambiri masiku ano
pakuti amene tikumpemphayo sali kutali ndi ife ndipo amamva chilichonse.
Surat7. AI-A'raf Juzu 8
327
Af>l
V tJyty Sjj-
56. Ndipo musaononge padziko
Pambuyo popakonza. Mpempheni
(Mulungu) mwamantha ndi
Mwakhumbo. Ndithu, Chifundo
cha Mulungu chili pafupi kwa
(anthu Ake ) Ochita zabwino. 1
57. Ndipo lye ndi Yemwe
amatumiza mphepo kuti Ikhale
nkhani yosangalatsa patsogolo pa
Chifundo chake (mvula), kufikira
Mphepoyo itasenza mitambo
yolemera Yomwe tikuitumiza
kudziko lakufa. Ndipo kupyolera
mwa iyo tikutsitsa Mitundu
yosiyanasiyana ya Zipatso.
Momwemo ndimo Tidzawaukitsira
akufa. (Zonsezi) nkuti Inu
mukumbukire. 2
58. Ndipo m'nthaka yabwino
umatuluka mmera Wake
(mwachangu) mwachilolezo cha
Mbuye wake. Ndipo nthaka
yomwe ili yoipa siitulutsa (mmera
wake) koma Movutikira.
M'menemo ndi momwe
Tikuchifotokozera chivumbulutso
Momveka kwa anthu oyamika. 3
Chifundo cha Mulungu chimawafika anthu omwe amachitiranso chifundo
anzawo. Ndipo amene sachitira anzawo chifundo sangapezenso chifundo cha
Mulungu. Choncho tiyeni tilimbikire kuthandiza ofooka ndi osowa chithandizo.
Ngati sititero ndiye kuti chifundo cha Mulungu chidzakhala kutali nafe.
2 Mmene Mulungu amaiukitsira nthaka youma ndi madzi amvula, nameretsa
mmera wosiyanasiyana, momwemonso ndimo adzawaukitsira akufa. Palibe
chimene chingamkanike.
3 Mmene ilili nthaka yopanda chonde pomeretsa mmera movutikira
nchimodzimodzi ndi anthu oipa. Nkovuta kuwaika panjira yabwino. Koma
tisatope ndi kutaya mtima nawo. Tiyesetsebe kuwakokera kunjira yabwino.
Surat7. Al-A'raf
Juzu 8
328
A ftjJt-i
V u>1y>Vl 5jj-
59. Ndithudi, tidamtumiza Nuhi
kwa anthu ake. (lye) adati: "E inu
anthu anga! Pembedzani Mulungu.
Inu mulibe Mulungu wina koma
lye. Ine Ndikukuoperani chilango
Cha tsiku lalikulu.
60. Akuluakulu a mwa anthu
Ake adati: "Ndithu Ife tikukuona
kuti uli m'kusokera Koonekera
(potiletsa izi Zomwe tidawapeza
nazo Makolo athu)."
61. (lye) adati: "E anthu anga!
Palibe Kusokera mwa ine. Koma
ine ndine Mtumiki wochokera
kwa Mbuye Wazolengedwa!
62. "Ndikufikitsa kwa inu
uthenga Wa Mbuye wanga.
Ndiponso ndikukulangizani; ndipo
ndikudziwa zochokera Kwa
Mulungu zomwe inu
simukuzidziwa."
63. "Kodi mukudabwa
kukudzerani Ulaliki wochokera
kwa Mbuye Wanu kudzera mwa
munthu Wa mwa inu, (yemwe
wadza) kuti Akuchenjezeni ndikuti
muope (Mulungu) Ndikutinso
muchitiridwe chifundo?"
64. Koma adamtsutsa. Choncho,
Tidampulumutsa iye ndi amene adali
Naye pamodzi m'chombo. Ndipo
Tidawamiza aja adatsutsa aya zathu.
Ndithudi, iwo adali anthu akhungu. 1
^'^'igiZj
1 Nkhani ya Mneneri Nuh paliponse akuifotokoza motalikitsa. Koma m'sura iyi
aifotokoza mwachidule. Ndipo Nuh ndi mneneri wakale kwabasi. lye adali
Siirat 7. Al-A'raf Juzu 8
329
A *>i
v sJ\j*H\ Sj^-
65. Ndipo kwa Adi
(tidaatumizira) M'bale wawo
Hud. Adati: "E inu Anthu anga!
Mpembedzeni Mulungu. Mulibe
Mulungu wina koma lye basi.
Kodi simungaope?"
66. Akuluakulu a mwa anthu
ake omwe Sadakhulupirire
adanena: "Ife Tili kukuona kuti uli
mu umbuli Ndipo ife
tikukuganizira kuti ndiwe
M'modzi wa a bodza."
67. (lye) adati: "E inu anthu
anga! Palibe umbuli mwa ine.
Koma Ine ndine Mtumiki
wochokera Kwa Mbuye
wazolengedwa."
68. "Ndikufikitsa kwa inu
uthenga wa Mbuye wanga. Ndipo
ine ndine Mlangizi wanu
(wokufunirani zabwino),
Wokhulupirika."
69. Kodi mukudabwa
pokudzerani ulaliki Kuchokera
kwa Mbuye wanu kupyolera Mwa
munthu wochokera mwa inu kuti
Akuchenjezeni? Kumbukirani
(Mtendere wa Mulungu) pamene
Adakuikani kukhala
®r.' -'■
kuwalalikira anthu a ku Iraq. Ndipo m'nthawi imeneyo pafupifupi dziko lonse
lapansi chitukuko chidali ku Iraq monga momwe tikuwerengera m'mabuku
ambiri yakale. Ndipo Mtumiki wamkulu yemwe adamtsogolera Nuh, ndi Idriss.
lye adali ku Egypt (Misir). Egypt ndi Iraq ndi maiko oyamba kukhala ndi midzi
ikuluikulu yotukuka.
Surat7. Al-A'raf
Juzu 8
330
A *>!
V ^jt'y «j>-
Amlowam'malo pambuyo pa
anthu a Nuhu, Ndipo
akuonjezerani pachilengedwe
kukhala amisinkhu italiitali ndi
amphamvu. Kumbukiraninso
mtendere wa Mulungu (pothokoza)
kuti mupambane."
70. Iwo adati: "Kodi watidzera
kuti Timpembedze Mulungu yekha
ndikusiya Zomwe ankapembedza
makolo athu? Tabwera ndi
chimene ukutilonjezacho Ngati uli
mmodzi mwa onena zoona."
71. (lye) adati: "Palibe chikaiko,
Chilango ndi mkwiyo wochokera
kwa Mbuye wanu zakugwerani.
Kodi Mukukangana nane pa
zamaina (a Mafano) omwe
mudawatcha inu ndi Makolo anu,
pomwe Mulungu sadatsitse
Umboni uliwonse pa milungu
yanu Yabodzayo? Choncho,
dikirani. Inenso ndili pamodzi
nanu mwa odikira."
72. Tidampulumutsa pamodzi
ndi amene Adali naye mwa
chifundo chathu, Ndipo tidadula
mizu ya omwe adatsutsa
Zivumbulutso zathu.Ndipo sadali
okhulupirira.
73. Kwa Asamudu tidamtumiza
m'bale wawo, Swaleh adati: "E inu
anthu anga! Gwadirani Mulungu;
inu mulibe mulungu Wina koma
a>9
®2$&t£*
Surat7. Al-A 4 raf
Juzu 8
331 * *>»
V d>\y>H\ ojj--
lye basi. Chizindikiro Chochokera
kwa Mbuye wanu chadza kwa Inu.
Iyi ndi ngamira ya Mulungu
monga Chisonyezo chanu
(chizizwa chanu), Choncho, isiyeni
izidya m'dziko la Mulungu, ndipo
musaikhudze ndi choipa Kuopera
kuti chingakugwereni Chilango
chowawa kwambiri.
74. "Ndipo kumbukirani
(Mulungu) pamene Adakupangani
kukhala amlowam'malo Pambuyo
pa mtundu wa Adi. Ndipo
Adakukhazikani pa dziko
mwaubwino. Mukudzimangira
nyumba zikuluzikulu Mchigwa,
ndiponso kusema ndi Kuboola
mapiri kukhala nyumba. Choncho
Kumbukirani mtendere wa
Mulungu, ndipo Musaononge
padziko pofalitsa chisokonezo."
75. Adanena akuluakulu omwe
adali Odzitukumula mwa anthu
ake kuuza Omwe
adaponderezedwa kwa amene adali
Okhulupirira (Mulungu) mwa iwo:
"Kodi muli ndi chitsimikizo Kuti
Swaleh ngotumizidwa ndi Mbuye
Wake (wapatsidwa utumiki)?
(Iwo) Adati: "Ndithu ife
tikukhulupirira Zomwe watumidwa
nazo (kuzifikitsa Kwa ife)."
76. Omwe adadzitukumula
Adati: "Ndithu ife Tikuzikana
zomwe wazikhulupirirazo".
9 "9h m $C *?'\$i 1 ml ftf^
>}9
Siirat7. Al-A'raf Juzu 8
332
A frjJUi
V Jljpty 5jj~»
77. Choncho adaipha
(adaizinga) Ngamira ndi kunyoza
lamulo la Mbuye Wawo, nati: "E
iwe Swaleh! Tibweletsere
(chilango) chimene Wakhala
ukutilonjeza ngati Ulidi mmodzi
waotumidwa."
78. Choncho, chivomerezi
chidawagwira Mwadzidzidzi,
adapezeka Ali, akufa chigwadire
NT nyumba zawo.
79. Tero, Swaleh adawasiya
(nkupita Kwina kwake) uku
akunena: "E Anthu anga!
Ndidafikitsadi uthenga Wa Mbuye
wanga kwa inu. Ndipo
Ndidakuchenjezani ndi
kukulangizani. Koma inu simufuna
alangizi."
80. Nayenso Luti (tidamtuma
ndipo kumbuka) Pamene adati kwa
anthu ake: "Kodi Mukuchita
chonyansa chomwe
Sadakutsogolereni aliyense
Kuchichita mwa anthu akale
M'zolengedwa zonse?"
81. "Ndithu inu mukuchita
Chisembwere ndi Amuna anzanu
kusiya Akazi!Ndithudi, Inu ndinu
anthu olumpha malire."
82. Kuyankha kwa anthu ake
sikudali kwa mtundu wina koma
kuti: "Apirikitseni m'mudzi wanu.
Ndithu iwowo Ndi anthu
»< J / l» // '"'-.'Ir'i!il 9£f*
©£aC#I
Surat7. Al-A'raf Juzu 8
333
A ftji-i
V sJ\jt*i\ dj>-
odziyeretsa. (Choncho akhaliranji
m'mudzi Wauve? Akakhale ndi
anzawo Ochita zaukhondo)"
83. Koma tidampulumutsa lye
ndi banja Lake, kupatula mkazi
Wake; adali m'gulu Laotsalira
m'mbuyo (adaonongeka).
84. Ndipo tidatsakamula Pa iwo
chimvula (Chamiyala). Choncho,
Taona mmene adaliri Mapeto a
anthu oipa.
85. Nakonso kwa anthu aku
Madiyana, (Tidamtumiza) m'bale
wawo Shuaib. Adati: "E inu anthu
anga!. Gwadirani Mulungu.
Mulibe Mulungu wina koma lye
basi. Chitsimikizo chadza
Kuchokera kwa Mbuye wanu.
Choncho pimani miyeso (Yanu ya
mbale) ndi Masikelo
m wachi lungamo .
Musawachepetsere anthu Zinthu
zawo; ndipo musaononge Dziko
pambuyo polikonza . Kutero ndi
Kwabwino kwa inu ngati muli
okhulupiriradi.
86. Ndipo musamawakhalire
anthu panjira mowabisalira ndi
kumawaopseza Ndi kuwatsekereza
kuyenda pa njira ya Mulungu
amene amkhulupirira lye, Ndi
kufuna kuikhotetsa njirayo (kuti
Anthu asaitsate). Ndipo
kumbukirani Adakuchulukitsani.
Surat7. Al-A'raf
Juzu 9
334
^ *>i
V cJly^M 3jj-
Taonani momwe Adalili mapeto a
owononga.
87. "Ndipo ngati pali gulu la
anthu Mwa inu amene akhulupirira
uthenga Umene ndatumidwa nawo,
ndi gulu la Anthu limene
silidakhulupirire, pirirani Mpaka
Mulungu aweruze pakati Pathu.
lye Ngwabwino poweruza Kuposa
oweruza."
88. A kuluakulu a omwe
adadzikuza Mwa anthu ake,
adanena: "Tikupirikitsa. E! Iwe
Shuaib m'mudzi mwathu Muno
ndi amene akhulupirira Pamodzi
nawe, pokhapokha Mutabwerera
kuchipembedzo Chathu." (lye)
adati: "Kodi ngakhale Kuti
tikuchida?"
89. "Ngati titabwerera
mchipembedzo chanu Pambuyo
potipulumutsa Mulungu
m'menemo, Ndiye kuti tampekera
Mulungu bodza. Sikungatheke kwa
ife kubwerera M'chipembedzo
chimenecho pokhapokha Atafuna
Mulungu, Mbuye wathu. Mbuye
wathu Ngodziwa zonse. Ndipo
kwa Mulungu yekha ndiko
Tayadzamira. Mbuye Wathu!
Weruzani mwachoonadi pakati
Pathu ndi pakati pa anthu athu. Inu
Ngabwino poweruza kuposa
oweruza."
^3
si
Surat7. Al-A'raf
Juzu 9
335
* fr>i
V >J\je>H\ ijj~>
90. Ndipo akuluakulu mwa
anthu ake omwe Sadakhulupirire
adati: "Ngati mutsatira Shuaibu
Pamenepo ndiye kuti inu mukhala
otayika."
91. Choncho chivomerezi
chidawaononga Mwadzidzidzi
motero adapezeka akufa
Chigwadire kunyumba zawo.
92. Amene adamutsutsa
Shuaibu adakhala ngati
Sadakhalepo m'mudzimo. Amene
adamutsutsa Shuaibu ndi omwe
adali otayika.
93. (Pamene nthawi
yakuonongeka kwawo
Idayandikira, Shuaibu adatuluka
M'mudzimo pamodzi ndi aja
Adakhulupirira) nawasiya oipawo
(Kunka kutali) uku akunena, "E
Inu anthu anga! Ndinafikitsadi
uthenga wa Mbuye Wanga ndipo
Ndinakuchenjezani ndiye Nchotani
ndiwadandaulire anthu okanira
94. Ndipo palibe pamene
tidamtuma mneneri Aliyense
m'mudzi uliwonse (nkumukana
anthu A m'mudzimo) koma
tinkawalanga eni Mudziwo ndi
masautso ndi mavuto kuti afatse
(Ndi kulambira Mulungu; koma
ayi adakanika).
95. Kenako tinasintha pamalo
pa choipa Pobweretsapo chabwino,
**
&&\#&\Gm&'£
Surat7. Al-A'raf
Juzu 9
336
% fr>i
V d>ly^l o^j--
(tidawachotsera Masautso ndi
mavuto ngakhale sadali
Okhulupirira) mpaka anachuluka,
ndi Kuchulukanso chuma chawo;
anayamba Kunena kuti: "Masautso
ndi mavuto Adawakhudzaponso
makolo athu. (Zoterezi
Sizachilendo kwa ife)." Choncho
tidawaononga Mwadzidzidzi
asakudziwa.
96. Chikhala kuti eni midziwo
Adakhulupirira naopa (Mulungu
pamene Aneneri adawadzera),
tikadawatsekulira Madalitso
ochokera kumwamba ndi Pansi.
Koma adakana (ndi kutsutsa
Aneneri) ndipo tidawaononga
chifukwa Cha zoipa zomwe
ankachita. l
97. Kodi anthu a m'mizinda
(iyo momwe Muli anthu oipa) ali
ndi chitetezo Cholimba kuti
chilango chathu Sichingawadzere
usiku iwo ali mtulo?
98. Kapena anthu a
m'mizindayo ali ndi Chitetezo
cholimba kuti chilango Chathu
sichingawafike masana uku Iwo
akusewera?
99. Kodi akudziika pa chitetezo
ku Chilango cha Mulungu?
Sangadziike Pa chitetezo ku
1 Apa tanthauzo lake nkuti akanapeza mtendere wambiri pompano padziko
lapansi akadakhala kuti adali olungama.
Surat7. Al-A'raf
Juzu 9
337 * *>
V Jl^pty ojj-*
chilango cha Mulungu Kupatula
anthu otayika basi.
100. Kodi sadadziwe awa omwe
alandira Dziko molowa mmalo
pambuyo pa Eni dzikolo (anthu
akale) kuti Tikadafuna tikadawaika
m'masautso Chifukwa cha
machimo awo ndi Kuwadinda
mitima yawo kotero iwo
Sakadamva (kanthu)?
101. Iyo ndi midzi (ikuluikulu)
yomwe Tikukusimbira iwe zina
mwa nkhani Zake. Ndithudi,
adawadzera aneneri Awo ndi
zizindikiro (zoonekera Poyera
zosonyeza kuti iwo ndi atumiki A
Mulungu). Koma sadali oti
nkukhulupirira Pa zomwe
adazitsutsapo kale. Umo ndi
Mmene Mulungu amadindira ndi
kuitseka Mitima ya osakhulupirira
(kotero kuti Sangathandizike ndi
malangizo a mtundu Uliwonse).
102.Ndipo ambiri a iwo
sitidawapeze Akukwaniritsa
lonjezo lililonse koma Tidawapeza
ambiri a iwo ali opandukira
Chilamulo cha Mulungu.
103. Pambuyo pawo
(aneneriwo) tidamtumiza Musa
pamodzi ndi zizindikiro zathu Kwa
Farawo ndi nduna zake, koma
Adazikana (zizindikirozo).
Choncho Taona momwe adalili
mathero aoononga
»'**<wi
Surat7. Al-A'raf
Juzu 9
338
* *>i
v >J\j*H\ Sj^
104.Ndipo Musa adati: "E iwe
Farawo! Ine ndine mthenga
wochokera kwa Mbuye wa
zolengedwa zonse.
105. "Ndikofunika kwa ine kuti
ndisamnenere Mulungu
chilichonse koma choonadi Basi.
Ndithu ndakudzerani ndi
chizindikiro Choonekera
kuchokera kwa Mbuye wanu.
Choncho, aleke ndinke nawo ana a
Israeli."
106. (Farawo) adati: "Ngati
Wadza ndi Chizindikiro, Bwera
nacho (tichione), Ngati iwe ulidi
mmodzi Wa onena zoona."
107. Choncho adaponya ndodo
Yake pansi. Mwadzidzidzi,
Idasanduka njoka yooneka.
108.Ndipo adatulutsa dzanja
Lake pompo lidakhala Loyera,
lowala kwa oliona.
109. Nduna za mwa anthu a
Farawo zidati: "Ndithu, Uyu ndi
wamatsenga Wodziwa (kwambiri
zamatsenga)".
110. "Akufuna kukusamutsani
Mdziko mwanu. Nanga
mukuganiza zotani?"
111. (Iwo) adati (kwa Farawo):
"Muleke Pang'ono iye ndi mbale
wakeyu (Usawaphe); ndipo tumiza
osonkhanitsa M'mizinda kuti
e,?>1 >»<?(' \Jt'1>' *
Surat7. AI-A'raf
Juzu 9
339
S *>i
V *JijP^I 5jj^
akusonkhanitsire (Amatsenga onse
akuluakulu)."
112."Kuti akubweretsere
Wamatsenga aliyense Wodziwa
kwambiri."
113. Amatsenga adadza kwa
Farawo; Nati: "Kodi ife tipeza
Malipiro ngati Titapambana?"
114. (Farawo) adati: "Inde,
Ndipo mudzakhala Mwa
oyandikitsidwa. (Mudzakhala
nduna zanga)."
115. (Amatsenga) adati: "E
iwe Musa! Kodi uyamba kuponya
ndiwe (matsenga ako Pamaso pa
anthu), kapena ife tikhale
Oyambirira kuponya?"
116. Musa adati: "Ponyani."
Choncho Pamene adaponya
adalodza maso a anthu
Ndikuwaopseza. Ndipo adadza
ndi Matsenga aakulu.
117. Ndipo tidamzindikiritsa
Musa ndi Chivumbulutso (Kuti):
"ponya ndodo Yako." Pompo iyo
Idameza zamatsengazo.
118. Choncho, choonadi
chidaimirira (Chidatsimikizika).
Ndipo zidapita Pachabe zomwe
ankachita.
119. Choncho adagonjetsedwa
Pamenepo, Nakhala onyozeka.
, t£.'i4'
®j&j£Ch'£&
9\ m ' 9 9 /f • ' 9l 9S9C 9 if
E /^/J/i^r^/t / < \**' %»'9 *£,*
Sta^^tie^)^
Surat7. Al-A'raf
Juzu 9
340
^ *>i
V ui^Sl 5j>-
120.Ndipo amatsenga
adadzigwetsa Uku akulambira
(Mulungu).
121. Adati: "Takhulupirira Mwa
Mbuye wa Zolengedwa zonse."
122. "Mbuye wa Musa Ndi
Haaruna."
123. Farawo adati:
"Mwamkhulupirira Chotani iye
ndisanakupatseni chilolezo?
Ndithu, iyi ndi ndale yomwe
mwaichita Mu mzindamu (inu ndi
Musa) kuti Muwatulutsemo eni
mzindawo. Koma Posachedwa
mudziwa (chimene ndikuchiteni)."
124."Ndithudi, nditseteka
manja anu ndi Miyendo yanu
mosinthanitsa: (kudulaDzanja
lakudzanjadzanja ndi mwendo
Wakumanzere, kapena dzanja la
Kumanzere ndi mwendo
wakudzanjadzanja). Kenako
ndikupachikani nonsenu."
125. (Iwo) adati: "Ifekwa
Mbuye wathu nkobwerera".
126. "Komatu palibe choipa
chimene waona mwaife Kupatula
kuti takhulupirira zizindikiro za
Mbuye Wathu pamene zatidzera. E
Mbuye wathu! Titsanyulireni
chipiriro, ndipo tipatseni Imfa uku
tili Asilamu (ogonjera Inu)."
i> {£$$* ?>2J1 <j$5
& &^v£jS2(gte
&u&VV£P Vim
Surat7. AI-A'raf
Juzu 9
341
* *>i
V Jljfrty 5jJ-rf
127. Ndipo nduna za mwa anthu
a Farawo Zidati (kwa Farawo):
"Kodi umuleka Musa ndi anthu
ake kuti abwere ndi Chisokonezo
m'dziko, ndi kuti akusiye iwe ndi
Milungu yako (yomwe
adatilangiza makolo athu Kuti
tipembedze pamodzi ndi iwe)?
(Farawo) Adati: "Tipha ana awo
achimuna ndikuwasiya Amoyo
(ana awo) achikazi. Ndithudi ife pa
Iwo tili ndi mphamvu
zowagonjetsera."
128. Musa adauza anthu ake:
"Pemphani Chithandizo kwa
Mulungu, ndipo Pilirani. Ndithu
dzikoli ndi la Mulungu; Alipereka
kwa amene wamfuna mwa
Akapolo ake. Ndipo mapeto
abwino Nga anthu olungama."
129. (Iwo) adati: "Takhala
tikuvutitsidwa Kale usanatidzere
ndiponso (tsopano) Pamene
watidzera." (Musa) adati: "Mwina
Mbuye wanu amuononga mdani
Wanu ndipo akulowetsani mmalo
mwawo M'dzikoli, ndi kuti aone
mmene Mungachitire."
130. Ndithu, tidawakhaulitsa
anthu A Farawo ndi chilala,
ndikuchepekedwa Zokolola; kuti
mwina angakumbukire.
131. (Adali chonchi): Ubwino
ukawadzera, Amati, "Ubwino wu
©
' '. *&>
Siirat7. Al-A'raf Juzu 9
342
^ *>i
v <J\j*H\ ojj^
nchifukwa chazochita Zathu
zabwino." Ndipo mliri woipa
Ukawadzera, amakankhira kwa
Musa Ndi amene adali naye.
(Amati iye Ndiye wadzetsa tsokalo
chifukwa Choisambula milungu
yawo). Dziwani Kuti tsoka lawo
limachokera kwa Mulungu
(chifukwa cha zochita zawo
Zoipa). Koma ambiri a iwo
sazindikira.
132. Ndipo adati (kwa Musa):
"Chisonyezo chilichonse Chimene
ungatibweretsere kuti utilodze
nacho (Siupindula kanthu). Ifetu
sitikukhulupirira. "
133. Choncho, tidawatumizira
chigumula, (Mliri wa) dzombe,
nsabwe, achule ndi Magazi monga
zizindikiro Zosiyanasiyana. Koma
adadzikuza; Ndipo adali anthu oipa.
134.Nthawi zonse chilango
chikawakhudza, Amati: "E iwe
Musa! Tipemphere kwa Mbuye
wako pazomwe adakulonjeza.
Ngati utichotsera chilangochi,
ndithudi Tikukhulupirira, ndipo
tiwatumiza Pamodzi nawe ana a
Israeli (kuti unke Nawo kumene
ukufuna)"
135. Koma nthawi iliyonse
tikawachotsera Chilangocho
kufikira nthawi yawo Yomwe iwo
adzaifika, pompo iwo Amaswa
lonjezo.
•9" M} \'*94\CCt' tji <'9&1 K> *K
Siirat7. Al-A'raf
Juzu 9
343 * *>»
V sJ\j*H\ 5jj-
136. Choncho, tidawabwezera
chilango Ndikuwamiza m'nyanja
chifukwa Chakuti iwo adatsutsa
zizindikiro zathu, Ndipo sadali
ozilabadira.
137. Ndipo tidawalowetsa
mmalo mwa anthu Omwe adali
kuponderezedwa kuvuma kwa
Dziko ndi kuzambwe kwake,
lomwe Tidaikamo madalitso
(ambiri). Ndipo Mawu abwino a
Mbuye wako Adakwaniritsidwa
kwa ana a Israeli, Chifukwa cha
kupirira kwawo (pazomwe
Adakumana nazo). Ndipo
tidazigumula Ndikuziononga
zomwe Farawo ndi anthu Ake
ankapanga ndi zomwe ankamanga.
138. Ndipo tidawaolotsa ana a
Israeli panyanja (Ndi kupulumuka
kumasautso a Farawo) Nadza kwa
anthu omwe adali kupembedza
Mafano awo. (Iwo) adati kwa
Musa: "E iwe Musa! Nafenso
tipangire milungu (yamafano)
Monga milungu yomwe ali nayo
iwo." (Mneneri Musa) adati:
"Ndithudi, inu ndinu Anthu
osazindikira.
139. "Ndithudi awa
aonongedwa NT zomwe ali nazozi,
Ndiponso ndizachabe Zomwe
akhala akuchita.".
9< 9 ' "\2X' } s' 9 4"±\9)' ' \*
">U 9'i?Zv'/\'<' L99 &' J 9S9*
Surat7. Al-A'raf Juzu 9
344
^ *>i
V (Jl^pty Qjj^
140. Adati: "Kodi ndikufunireni
mulungu Wina kusiya Mulungu
chikhalirecho lye wakuchitirani
zabwino zoposa Pa zolengedwa
zonse?."
141. Ndipo kumbukirani
pamene Tidakupulumutsani
(m'manja) mwa anthu A Farawo
omwe adali kukuzunzani ndi
chilango Choyipa ndipo anali
kupha ana anu aamuna Ndi kusiya
ana anu aakazi. Pa ichi Padali
mayeso aakulu ochokera kwa
Mbuye wanu.
142. Ndipo tidamlonjeza Musa
masiku Makumi atatu (kuti achite
mapemphero Kuti kenako timpatse
Taurat). Ndipo Tidawakwaniritsa
ndi masiku khumi; Lidakwanira
pangano la Mbuye wake (Lopita
kukampatsa Tauratiyo) M'masiku
makumi anayi. Ndipo Musa adati
kwa m'bale wake Haaruna: "Lowa
m'malo mwanga pa
(kuwatsogolera) Anthu angawa.
Ndipo konza; usatsate njira Ya
oononga."
143. Pamene Musa adafika
kumalo achipangano Chathucho,
ndipo Mbuye wake namulankhula,
(Musa) adati: "Mbuye wanga:
Dzionetseni Kwa ine kuti
ndikuoneni." Mulungu adati:
"Sungathe kundiona; koma
yang'ana Phirilo (lomwe lili
9 ~~k\' 9 [ 9 Y ?>?i 9 i *.*A*i
Surat7. Al-A'raf
Juzu 9
345
^ *>»
v <J\j*H\ ojj~>
patsogolo pako). Ngati Likhazikika
pamalo pake (popanda kusweka),
Ukhoza kundiona." Choncho
Mbuye wake Pamene adadzionetsa
kwa phirilo adalichita Kukhala
loswekasweka ndipo Mussa
adagwa ndi Kukomoka. Pamene
adatsitsimuka adati: "(Ha!
Ndikutsimikizadi kuti) Inu ndinu
Wolemekezeka. Ndalapa kwa Inu,
ndipo ndine woyamba mwa
Okhulupirira (izi)".
144. (Mulungu) adati: "E iwe
Musa! Ndithu Ine Ndakusankha iwe
mwa anthu onse, (Kukusankhira)
uthenga Wanga ndi Kuyankhulana
Nane. Choncho landira Chimene
ndakupatsa, Ndipo khala m'modzi
Wa anthu othokoza."
145. Ndipo tidamlembera
m'magome (m'masileti)
Maphunziro aulaliki wamtundu
uliwonse Wofotokoza chinthu
chilichonse: "Choncho, Agwire
mwamphamvu ndi kuwalamulira
Anthu ako kuti awagwire
mwaubwino wake. Posachedwapa
ndidzakusonyezani midzi yaoipa
Oswa malamulo athu (momwe
idaonongekera. Ndipo
Ndikulowetsani inu m'menemo)."
146. Ndiwapewetsera
kuzilingalira zizindikiro Zanga
awo omwe akudzitukumula
Padziko popanda choonadi, ndipo
Surat7. Al-A'raf Juzu 9
346
S c>i
V J>\j*H\ 5jj-
Akaona chizindikiro chilichonse,
Sachikhulupirira ndipo akaona
njira Yolungama, sakuiyetsa njira
(sakuitsata) Koma akaona njira
yosokera, akuiyetsa njira
(Akuitsata). Zimenezo nchifukwa
Chakuti iwo adatsutsa zizindikiro
Zathu ndipo anali osazilabadira.
147. Ndipo awo amene atsutsa
zivumbulutso Zathu ndi kukumana
m'tsiku lachimaliziro, Zochita
zawo zaonongeka. Kodi
adzalipidwa china kuposa Zomwe
adali kuchita?
148. Ndipo pambuyo pake
(popita Kukalandira Taurat), anthu
a Musa adaumba (fano la) thole
(mwana Wa ng'ombe) ndi
Zibangiri zawo za siliva Ndi
golide; yemwe adali ndi Thupi ndi
kumatuluka mawu (koma
Wopanda moyo). Kodi sakuona
kuti Ilo (fano lawolo)
silikuwalankhula. Ndiponso
silikuwaongolera njira (yabwino?)
Koma adalipanga basi (kuti likhale
Mulungu wawo wa fano) potero
adali Kudzichitira okha zoipa.
149. Pamene adazindikira
kulakwa kwawo, (Anadandaula
kwambiri) naona Kuti iwo asokera,
anati: "Ngati Mbuye Wathu
satimvera chisoni ndi
Kutikhululukira, ndithudi, tikhala
mwa Otaika (oonongeka)."
Sfi
Surat7. Al-A'raf Juzu 9
347
^ *>i
V uJly^l ojj-
150. Ndipo pamene Musa
adabwerera kwa anthu ake ali
wokwiya, wodandaula (pomva
Zomwe zidachitikazo), adati:
"Umlowam'malo wanu womwe
mudandichitira pambuyo panga,
ngoipa zedi. Kodi
mudalifulumirira lamulo la Mbuye
Wanu; (mudachita zanuzanu
musanadziwe Chimene
angakulamulireni Mulungu wanu)?
Ndipo adawaponya pansi
magomewo (Momwe
mudalembedwa malamulo a
Chipembedzo chake). Nagwira
mutu wa M'bale wake nkuukokera
kwa iye. (kufuna kummenya
chifukwa chamkwiyo umene adali
nawo. M'bale wakey o) adati: "E
I we mwana wa mayi anga! Ndithu,
Anthu (awa) adandiyesa wofooka,
Potero (sadamvere malangizo
anga). Adatsala pang'ono kundipha.
Choncho Usawakondweretse adani
(ndi chilango chako) Pa ine,ndipo
usandiike pamodzi ndi anthu oipa".
151. (Musa) adati: "Mbuye
wanga! Ndikhululukireni ine ndi
m'bale wanga ndipo tilowetseni
m'chifundo chanu. Inu ndinu
Achifundo kuposa achifundo
Onse."
152. Ndithu, omwe adapanga
(fano la ) Thole uwafika mkwiyo
Wa Mbuye wawo ndi kunyozeka
Surat7. Al-A'raf
Juzu 9
348
* *>t
v ij\j**i\ Sjj-
Pamoyo wadziko lapansi.
M'menemo Ndi mom we
timawalipirira Anthu opeka (zinthu
za chipembedzo).
153.Ndipo omwe adachita
zoipa, kenako Nkulapa pambuyo
pake nakhulupirira Ndithu, Mbuye
wako pambuyo pakulapako,
Ngokhululuka Kwabasi,
Ngwachisoni.
154. Pamene mkwiyo wa Musa
udatotobwa, adatola magome aja
omwe m'malembo Mwake mudali
chiongoko ndi chifundo kwa omwe
amaopa Mbuye wawo.
155.Ndipo Musa adasankha
anthu ake Makumi asanu ndi awiri
(70 omwe adali amakhalidwe
abwino) kuti akafike kumalo a
chipangano chathu (Chimene
tidamuuza kuti akabwere Nawo pa
phiripo kuti akapemphe
Chikhululuko pamachimo awo
omwe adachitidwa ndi anzawo
oipa). Ndipo pamene chivomerezi
Chachikulu chidawafika (adatsala
Pang'ono kufa). (Musa) adati:
"Mbuye wanga! Ngati mukadafuna
Mukadawaononga iwo ndi ine
Kale (pamaso pa anzawo onse kuti
adzionere okha kuti amwalira ndi
Mphamvu za Mulungu, osati
Pakuwapha Ine). Kodi mutiononga
chifukwa chazochita za mbuli
zathu? Izi Sichina koma ndi
«S$ftcASbg
Surat7. Al-A'raf Juzu 9
349
^ frjA-i
V <J\j*H\ ojj^
mayesero anu. Kupyolera
M'mayeserowo mumamlekerera
kusokera amene mwamfuna, ndi
kumtsogolera amene Mwamfuna.
Inu ndiye Mtetezi wathu;
Choncho, tikhululukireni ndi
kutimvera Chifundo. Inu ndinu
Abwino Mwa okhululuka onse."
156. "Ndipo tilembereni
zabwino padziko lino lapansi ndi
patsiku lomaliza ndithudi
Tibwerera kwa Inu!" (Mulungu)
Adati: "Chilango changa
ndichifikitsa Kwa yemwe
ndamfuna (mwa anthu oipa);
Ndipo chifundo changa
chakwanira Pachilichonse (pa
abwino ndi oipa). Koma
ndiwalembera (kuti mtendere
Umenewu udzakhale wawowawo
patsiku lachimaliziro). Amene
akupewa (zoletsedwa) ndi
Kumapereka Zakat, ndi
kumakhulupirira Zizindikiro zathu;
157. "Omwe akutsata Mtumiki,
mneneri Wosatha kuwerenga ndi
Kulemba. (Ngakhale ali choncho,
Akuphunzitsa zophunzitsa
Zodabwitsa); yemwe akumpeza
Atalembedwa kwa iwo m'Buku la
Taurat ndi Injili, akuwalamula
Zabwino ndi kuwaletsa zoipa, Ndi
kuwaloleza zabwino ndi
Kuwaletsa zodetsedwa (zoipa);
Ndi kuwatula mitolo yawo ndi
Surat7. Al-A'raf Juzu 9
350
<\ *j±-l
V <J\j*V\ Sjj-,
Magoli omwe adali paiwo
(malamulo Ovuta kuwatsata).
Choncho, amene Amkhulupirira
(Muhammad {SAW})Ndi
kumamlemekeza ndi
kumuthangata natsata Kuunika
(Qur'an) komwe
kudavumbulutsidwa Pamodzi ndi
iye, iwo ndiwo opambana."
158.Nena: "E inu anthu! Ine
ndine Mtumiki wa Mulungu kwa
inu nonse. (Mulungu) yemwe ali
nawo ufumu Wa kumwamba
ndipansi. Palibe Wopembedzedwa
mwa choonadi koma Iye.
Amapatsa moyo ndi imfa.
Choncho, Khulupirirani mwa
Mulungu ndi Mtumiki Wake
yemwe ndi Mneneri Wosadziwa
kulemba ndi kuwerenga, yemwe
Akukhulupirira Mulungu ndi
mawu Ake. Ndipo Mtsatireni kuti
muongoke."
159. Ndipo mwa anthu a Musa,
adalipo Omwe adali kutsogolera
anzawo ku Choonadi. Ndipo ndi
choonadicho Ankachita
chilungamo.
160. Ndipo tidawagawa iwo
m'mafuko Khumi ndi awiri
(osiyanasiyana) Monga mitundu
ikuluikulu. Ndipo
Tidamuvumbulutsira Musa
pamene Anthu ake adampempha
Surat7. Al-A'raf Juzu 9
351
<* *>i
V <J\j*^ djj^
madzi kuti: "Menya mwala ndi
ndodo yakoyo." Ndipo mudatuluka
akasupe khumi Ndi awiri mwakuti
fuko lililonse Lidadziwa malo ake
omwera. Ndipo Tidawaphimba ndi
mthunzi wamtambo, Ndi
kuwatumizira mana ndi
salwa(mbalame. Tidawauza):
"Idyani zinthu zabwinozi Zomwe
takupatsani." Komatu sadatichitire
Choipa (pamene adachita
zamphulupulu), Koma
adadzichitira okha zoipa.
161. Ndipo akumbutse pamene
adauzidwa: "Khalani mu Mzinda
uwu (Baitul Makadas, umene
takupatsani), ndipo Idyani
m'menemo paliponse pamene
Mwafuna, ndipo nenani (polowa
Mumzindamo uku mutawerama):
"Tifafanizireni machimo athu, (O!
Inu Mbuye wathu)." Ndipo
Lowerani pachipata (chake)
Modzichepetsa; tikukhululukirani
zolakwa zanu Ndipo tiwaonjezera
Zabwino ochita zabwino.
162. Koma aja amene
adadzichitira okha Zoipa, mwa iwo
adasintha mawu ena Kusiya omwe
adauzidwa; choncho,
Tidawatumizira chilango
chochokera Kumwamba chifukwa
chodzichitira Okha zoipa.
163. Tawafunsani nkhani ya
mudzi umene Udali m'mphepete
&p>-^
*1\
© cy^^-^uJI
#.
&%Z&J\1£3\&£&Z
Siirat7. Al-A'raf
Juzu 9
352
<\ *>i
V cily^l Ojj~-
mwa nyanja; (Anthu
Am'mudziwo) pamene adali
kuswa (Lamulo la) tsiku la Sabata
(lomwe Adauzidwa kuti patsikuli
asamachite Usodzi wa nsomba,
koma m'malo mwake Azichita
mapemphero okha). Nsomba Zawo
zinkawadzera yandayanda Patsiku
la Sabata, koma patsiku Lomwe
silidali la Sabata sizidali
Kuwabwerera (yandayanda).
Motero Tidawayesa mayeso
chifukwa chakuchimwa Kwawo.
164.Ndipo (akumbutse )
pamene anthu ena Mwaiwo
ankanena (kwa omwe amachenjeza
Amene adaswa kupatulika kwa
tsiku la Sabata pamene adati):
"Pali Phindu lanji kuwachenjeza
anthu omwe Mulungu awapha
kapena kuwalanga Ndi chilango
chaukali pompano Padziko
lapansi)? (Iwo) adati: "Kuti
Tidzakhale ndi chidandaulo kwa
Mbuye Wathu (ponena kuti
tidawachenjeza Koma
sadatimvere) ndi kutinso mwina
Angaope (Mulungu nasiya kuswa
lamulo Lake)".
165. Choncho, pamene
sanalabadire zimene Anauzidwa
ndi kuchenjezedwa,
Tinawapulumutsa (anthu) omwe
amaletsa Zoipa, ndipo
tidawakhaulitsa amene
S&^A.
ssa^yssuiiS^
Surat7. Al-A'raf
Juzu 9
353
* *>»
V J\jfiH\ *jy~>
Ankadzichitira okhazoipa ndi
chilango Choipa kwambiri
chifukwa Chakunyoza kwawo.
166. Pamene anadzikweza
Pakusasiya zimene Analetsedwazo
tidawauza: "Khalani anyani,
Oyaluka (paliponse)."
167. Ndipo (akumbutse)
pamene Mbuye wako Analengeza
(kuti) adzawatumizira iwo (Ayuda)
anthu mpaka tsiku la Kiyama,
omwe adzawazunza ndi Mazunzo
oipa. Ndithu, Mbuye wako
Ngofulumira kulanga. Ndipo
palibe chikaiko, lye Ngokhululuka
kwambiri, Ngwachifundo
chambiri.
168. Ndipo tidawalekanitsa
pakati pawo (Ayuda), ndi
kuwabalalitsa padziko Lonse
mafuko osiyanasiyana, Ena mwa
iwo abwino (olungama) Ndipo ena
sali choncho (oipa). Tinawayesa
mayeso a zabwino ndi Zoipa kuti
abwerere. (Koma ayi,
Sanabwerere).
169. Choncho,anawatsatira
pambuyo (Anthu abwinowo),
otsatira atsopano Nalandira Buku
(la Mulungu nalowa Mmalo mwa
iwo koma popanda Kulitsata ndi
kulilingalira). Ankatenga Zinthu
zoletsedwa za padziko lapansi uku
akunena: "Tidzakhululukidwa,
Surat7. Al-A'raf
Juzu 9
354 * *&
V Jijpty *jj--
(Mulungu adzatikhululukira)."
Ngati Zina zonga izo zitawapeza,
amazitenganso. Kodi
silidatengedwe pangano kwa iwo
La m'Buku kuti sadzamunenera
Mulungu Bodza koma zoona
zokhazokha? (Nanga Akuneneranji
kuti Mulungu adzawakhululukira
Pomwe akupitiriza machimo?)
Pomwe iwo Aphunzira zomwe zili
mmenemo. Komatu nyumba ya
chimaliziro idzawakhalira bwino
amene akuopa (Mulungu). Nanga
Bwanji simukuzindikira?
170.Ndipo amene akugwirisitsa
Buku (la Mulungu Potsata
zophunzitsa zake)
ndikumapemphera Swala,
(tidzawalipira zabwino). Ndithu,
Ife sitipititsa pachabe malipiro a
ochita zabwino.
171.Ndipo(akumbutse) pamene
tidalizula phiri Ndikulinyamula
pamwamba pawo Monga denga
(kapena mtambo umene
Wawavindikira) natsimikiza kuti
Liwagwera, (tidawauza):
"Landirani, Mwamphamvu
malamulo amene Takupatsani,
ndipo kumbukirani Zomwe zili
m'menemo (pozitsata ndi
Kuzichita); kuti inu muope."
172, Ndipo (kumbukirani)
pamene Mbuye wako
Adawatulutsa ana a Adam
txs&s^y&&
9 "Sf9.'< 9 '\l'<'S\i\'
Surat7. AI-A'raf
Juzu 9
355
* *>i
V Ji^SM ojj--
m'misana Ya atate awo ndi
kuwachititsa umboni okha
(Powauza kuti): "Kodi ine sindine
Muleri Wanu?" (Iwo adati:) u Inde
tikuikira umboni (kuti Inuyo ndiye
Mleri wathu)." (Mulungu
adawauza kuti): "Kuopera kuti
mungadzanene tsiku louka Kwa
akufa, "Ife sitidali kuzindikira
Chipanganochi (sitidali kudziwa
zimenezi)."
173. Kapena mungadzati:
"Makolo athu ndi amene
adapembedza mafano kale,ndipo
Ife tidali ana odza pambuyo pawo.
(Choncho tidawatsatira pazimene
ankachita). Kodi nanga
mutiononga chifukwa cha zomwe
Adachita oipa?"
174. M'menemo ndi mom we
tikulongosolera Mokwanira
zivumbulutso kuti mwina Iwo
angabwerere (kwa Mulungu).
175. Ndipo alakatulire nkhani za
yemwe Tidampatsa zizindikiro
zathu Nadzichotsa m'menemo
(m' zizindikiro), Ndipo Satana
namtsata iye choncho, Adali
m'gulu laosokera.
176. Ndipo tikadafuna
tikadamtukula Nazo (ulemerero
wake). Koma iye Adapendekera ku
za mdziko natsatira Zilakolako
zake. Fanizo lake lili ngati Galu.
'&£<&&&&&£*
Surat7. Al-A'raf
Juzu 9
356
* *jJH
V <Jly^l 5jj-
Ngati utamkalipira amathawa Uku
akutulutsa lirime lake kunja,
Ngakhale utamsiya amatulutsabe
kunja Lirime lake. Umo ndi
momwe chilili Chikhalidwe cha
anthu otsutsa zizindikiro zathu.
Choncho asimbire nkhani izi kuti
angalingalire.
177. Taonani kuipa fanizo la
anthu omwe Atsutsa zizindikiro
zathu ndi Kudzichitira okha zoipa.
178. Amene Mulungu
wamuongola ndiye Woongoka.
Ndipo amene wamulekerera
kusokera (Chifukwa chakusatsatira
kwake malangizo A Mulungu),
iwo ndiwo otaika (oonongeka).
179.Ndithudi, majini ambiri ndi
anthu Tidawalengera kukalowa
kumoto wa Jahannama. Mitima ali
nayo koma Sazindikira nayo
kanthu; ndipo maso Ali nawo
koma sapenyera nawo (Zodabwitsa
za Mulungu); ndipo Makutu ali
nawo koma samvera nawo
(Zowapindulitsa). Iwo ali ngati
ziweto, Kapena iwo ndi osokera
zedi kuposa Ziweto. Iwo ndi
osalabadira.
180. Ndipo Mulungu ali nawo
maina abwino. Choncho,muitaneni
ndi maina wo. Alekeni amene
akupotoza maina Ake
Posachedwapa alipidwa zomwe
akhala Akuchita
Surat7. Al-A'raf
Juzu 9
357
^ *>i
v *J\jP*i\ *jj~*
181. Ndipo mwa amene
tidawalenga, alipo Anthu
oongolera (anzawo) kuchoonadi.
Ndipo kupyolera mchoonadicho
Akuchita chilungamo.
182. Ndipo amene at sutsa
zivumbulutso Zathu, tiwalekerera
pang'onopang'ono, Kenako
nkuwakhaulitsa kuchokera
Momwe iwo sakudziwa.
183. Ndipo ndiwapatsa
Kanthawi. Ndithu, Kukhaulitsa
kwanga Nkokhwima.
184. Kodi sakulingalira
(nkuona) kuti Munthu wawoyo
(mneneri Muhammad{SAW})
Alibe misala? lye sichina chake,
Koma mchenjezi woonekera
poyera.
185. Kodi saona ufumu
wakumwamba ndi Pansi, ndi
zinthu zomwe Mulungu Adalenga?
Mwina mwake nthawi yawo
Yofera yayandikira. (Nanga
Adzalingalira liti zolengedwa za
Mulungu?) Kodi ndi nkhani iti
Pambuyo pa iyi (Qur'an) Imene
adzaikhulupirira?
186. Amene Mulungu
wamulekerera Kusokera, alibe
muongoli. Ndipo Mulungu
Akuwasiya akuyumbayumba
M'kusokera kwawo.
?■
Surat7. Al-A'raf Juzu 9
358 | * *>'
V <J\y>H\ 5jj-
187. Akukufunsa za nthawi (ya
Kiyama) Kuti idzakhalako liti?
Nena: "Kudziwika kwa nthawi
yake kuli Kwa Mbuye wanga.
Palibe amene Angaionetse poyera
nthawi yake Koma lye. Nkovuta
kwambiri Kumwamba ndi pansi
(kuizindikira Nthawi yake).
Siidzakudzerani Koma
mwadzidzidzi." Akukufunsa ngati
Kuti iwe udayesetsa kufufuza za
Nthawiyo. Nena: "Kudziwika Kwa
nthawi yake kuli kwa Mulungu.
Koma anthu ambiri sadziwa."
188. Nena: "Ine ndekha ndilibe
mphamvu Yodzibweretsera
chabwino kapena Kudzichotsera
choipa, koma chimene Mulungu
wafuna. Ndikadakhala kuti
Ndikudziwa za mseri,
ndikadadzichulukitsira Zabwino,
ndipo choipa Sichikadandikhudza.
Ine sindine China chake koma
ndine mchenjezi Ndi wouza anthu
okhulupirira nkhani zabwino."
189. lye ndi Yemwe
adakulengani kuchokera Mwa
munthu mmodzi, napanga mwa iye
Mkazi wake kuti adzikhala naye.
Pamene adamkumbatira, adakhala
ndi Pakati popepuka nayenda napo
(Mosalemedwa). Koma pamene
(pakatipo) Padalemera
(patangotsala pang'ono kuti
Abereke) anampempha Mulungu,
Surat7. Al-A'raf
Juzu 9
359
^ *>i
V cjly^t 5j^
Mbuye Wawo (kuti): "Ngati
mutipatsa mwana Wabwino
(wooneka ngati ife), ndithu
tidzakhala mwa Othokoza
kwambiri."
190. Choncho, pamene
adawapatsa mwana Wabwino
(yemwe adapempha) adamchitira
Mulungu anzake (mafano)
Pachimene Adawapatsacho.Koma
Mulungu Watukuka kuzimene
Akumphatikiza nazozo.
191.Kodi akumphatikiza
(Mulungu) ndi zinthu Zomwe
sizilenga chilichonse pomwe izo
Zikulengedwa? (Zikupangidwa ndi
manja awo).
192.Ndipo sizingathe
kuwathandiza ngakhale
Kudzithandiza zokha
(podzibweretsera Zabwino ndi
kudzichotsera zoipa).
193. Ngati (milungu
yamafanoyo) mutaiitanira
Kuchiongoko, siingakutsatireni
(chifukwa chakuti Siimva kapena
kuzindikira chilichonse).
Nchimodzimodzi kwainu kuiitana
kapena kukhala chete (Palibe
chimene ingadziwe).
194, Ndithu, amene
mukuwapembeza kusiya Mulungu,
ndi akapolo monga inu. (Koma Inu
muposa iwo). Choncho aitaneni
®
j>$-wd
r\' 9 ' 99 -'
Surat7. Al-A'raf
Juzu 9
360 ^ >>
V <J\j*V\ Sj^-
ndipo Akuyankheni ngati inu
mulidi oona (Pazimene
mukunenazi).
195. Kodi iwo ali nayo miyendo
yoyendera? Kapena ali nawo
manja ogwirira. Kapena Ali nawo
maso openyera? Kapena ali Nawo
makutu omverera? Nena:
"Aitaneni Aphatikizi anuwo, ndipo
kenako Ndichitireni chiwembu
ndipo Musandipatse nthawi."
196. "Ndithu Mtetezi wanga ndi
Mulungu, Yemwe wavumbulutsa
Buku (Hi Lopatulika). Ndipo lye
amawateteza ochita zabwino.
197. "Ndipo omwe
mukuwapembedza Kusiya lye
(Mulungu,) sangathe
Kukupulumutsani ndiponso
Sangathe kudzipulumutsa okha."
198. Ngati mutawaitanira ku
chiwongoko, Sangamve; koma
uwaona Akukupenyetsetsa Iwe
pomwe iwo sakuona.
199. Gwiritsa kukhululuka (khala
Ndi khalidwe lokhululuka); ndipo
Lamula zabwino ndi kudzipatula Ku
(zochita) zambuli.
200. Ngati manong'onong'o a
Satana Atakuvutitsa, dzitchinjirize
ndi Mulungu. Ndithu lye
Ngwakumva; Ngodziwa.
201. Ndithu amene akuopa
(Mulungu), udyerekezi Wa Satana
®r.
' *99\ /■»>'&[
\&lS*SJ>**-v\
Surat7. Al-A'raf Juzu 9
361
H >>i
V uJly^l 5j^
ukawakhudza amakumbukira
(Mulungu), nkuona (njira yotulukira
Muudyerekezi wakewo).
202. Koma anzawo (omwe ali
oipa) amawalimbikitsa m'machimo,
ndipo Kenako saleka (kupitiriza
machimowo).
203. Ngati siudawabweretsere
chozizwitsa, Akunena: "Bwanji
wosachibweretsa Pa iwe wekha?
Nena: "Ndithudi Ndikutsatira
zimene zikuvumbulitsidwa Kwa ine
kuchokera kwa Mbuye wanga.
(Sindichita chinthu mwa ine
ndekha). Izi (aya za Qur'an) ndi
umboni (waukulu Pazoyankhula
zanga) wochokera kwa Mbuye
wanu. (Izo) ndi chiongoko Ndi
chifundo kwa anthu okhulupirira."
204. Ndipo Qur'an
ikamawerengedwa, Mvetserani
(mwatcheru) ndi kukhala Chete, kuti
muchitiridwe chifundo.
205. Mtchule Mbuye wako mu
mtima Mwako modzichepetsa mwa
Mantha ndi mosakweza Mawu
m'mawa ndi madzulo; Ndipo
usakhale mwa osalabadila
(Malamulo a Mulungu).
206. Ndithu amene ali kwa
Mbuye wako, (Angelo),
sadzitukumula posiya
Kumpembedza (Mbuye wawo,koma
Iwo) amam'lemekeza ndi
kumlambira.
a^^itfostftSi
Sin at 8. Al-Anfal
Juzu 9
362
* *>i
A JliiSlI «jj->
SURAT AL-ANFAL VIII „ j£*<
Sura ya Al Anfal idavumbulutsidwira ku Madina, iyoyi ili ndi
Ndime 75. Mulungu wafotokoza m'sura iyi ena mwa malamulo
a nkhondo ndi zomwe zingachititse kuti gulu lankhondo likhale
lopambana pa nkhondo yake.Yafotokozanso malamulo a chuma
chosiyidwa ndi adani mmene angachigawire.
Surayi ikufotokoza za nkhondo ya Badiri mmene inachitikira
ndi chiyambi chake. Watchulanso Mulungu m' Surayi zakuti
Asilamu akhale okonzekera za nkhondo poopera kuti adani
angawadzere mwadzidzidzi ndikuti adani akafuna mtendere
Asilamu avomereze mtenderewo. Ndipo ikumaliza surayi
ponenetsa kuti Asilamu akhale otetezana okha, osadalira
chitetezo cha yemwe sali m'Msilamu.
Surat 8. Al-Anfal
Juzu 9
363
S *j*-i
A JUiSll «jj-*>
Surat Al-Anfal VIII
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Akukufunsa za chuma
cholandidwa Pankhondo (mmene
chingagawidwire). Nena: "Chuma
cholanda pa Nkhondo ndi cha
Mulungu ndi Mtumiki (ndi amene
ali olamula Kagawidwe kake);
choncho, Muopeni Mulungu ndipo
yanjanani Mwachibale pakati
panu. Mverani Mulungu ndi
Mtumiki wake, ngati Mulidi
okhulupirira." 1
2. Ndithu, okhulupirira,
weniweni ndi Amene akuti
Mulungu akatchulidwa Mitima
yawo imadzadzidwa ndi mantha;
Pamenenso aya zake
zikuwerengedwa Kwa iwo
zimawaonjezera chikhulupiriro,
Ndipo amayadzamira kwa Mbuye
wawo Yekha basi; (sakhulupirira
nyanga, Ndi mizimu ya anthu
akufa). 2
■f.l;
snffife
o^l^jJt^U-
-^
Nkhondo ya Chisilamu ndinkhondo yomenyera kuti chipembedzo cha
Chisilamu chisafafanizidwe ndi anthu ochida. Osati chifukwa chofuna kupeza
chuma. Asilamu adafunsa Mtumiki za kagawidwe kachuma cholanda
pankhondo ndipo anauzidwa kuti chuma cha pankhondo ncha Mulungu ndi
Mtumiki ndi amenenso angachigawe pakati pa Asilamu.
2 Apa patchulidwa ena mwamakhalidwe a Asilamu omwe ngokwanira
pachikhulupiriro chawo. Amene alibe makhalidwe otere, ndiye kuti chikhulupiriro
chawo nchosakwanira ndipo patsiku la chimaliziro sichidzawapindulira zabwino.
Surat 8. Al-Anfal
Juzu 9
364
^ *>i
A JUity $jj~-
3. Amenenso amaimirira
kupemphera Napereka chimene
tawapatsa, (Pa njira ya Mulungu,
ndikuthandiza Ovutika).
4. Awa (okhala ndi makhalidwe
otere) ndi Amene ali okhulupirira
mwachoonadi. Iwo adzapeza
ulemerero (wapamwamba) Kwa
Mbuye wawo, ndi chikhululuko
Ndi zopatsidwa zaulemu.
5. ( Chikhalidwe cha
Okhulupirirawa mkukanganirana
kwawo Zotolatola za pankhondo)
chikufanana ndi (Chikhalidwe
chawo) pamene Mbuye wako
Adakulamula kutuluka m'nyumba
yako (kupita Ku Badiri kukachita
nkhondo ndi osakhulupirira)
Mwachoonadi. Ndithu, gulu lina la
Asilamuwo silidafune (kuchoka
Kukakumana ndi adani). 1
6. Akutsutsana nawe (pa
chinthu) choona Pambuyo pakuti
chaonekera poyera. (Kukuwaipira
kukumana ndi adani) ngati Kuti
akubusidwa kunka ku imfa ali
kuona.
7. (Kumbukirani, E inu
okhulupirira!) Pamene Mulungu
anakulonjezani gulu Limodzi mwa
cuiU^ifeS^ifcWi
^<9 9 * '&* tftm'uK"* UK" 9
Pamene Asilamu adauzidwa kukakumana ndi Akuraishi kuti akamenyane
nawo nkhondo, ena mwa Asilamu adachita mantha chifukwa chakuti nthawiyi idali
yoyamba kwa iwo kuuzidwa zokamenyana ndi adani awo, poganiziranso.kuti
Akuraishi adali akatswiri pomenya nkhondo, ndiponso adali ochuluka zedi
kuposa iwo. Choncho Asilamu adayesera kupereka madandaulo awa ndi awa.
Surat 8. Al-Anfal Juzu 9
365
* *$r\
A JtfiSM Ojj--
M«(Kl
<?),
tag)9KjSb'
magulu awiri kuti likhale Lanu
(kuti mumenyane nalo). Koma Inu
mukufuna lopanda mphamvu kuti
Likhale lanu (kuti ndilo
mumenyane Nalo). Koma
Mulungu akufuna Kuchitsimikiza
choonadi ndi mawu Ake ndi
kudula mizu ya osakhulupirira,
(Pomenyana ndi gulu
lamphamvulo, Omwe ndi
ankhondo a Chikuraishi).
8. Kuti achitsimikizire
Choonadi ndi kuchichotsa
Chachabe; ngakhale Zikuwaipira
anthu oipa.
9. (Kumbukirani) pamene
mudali Kupempha Mbuye wanu
chithandizo, Ndipo anakuyankhani
kuti: "Ndithudi, Ine
ndikuthandizani ndi Chikwi cha
Angelo otsatizana Potsika,
(omenya nkhondo)."
10. Ndipo Mulungu sadachite
ichi koma Kuti chikhale nkhani
yabwino (Yosangalatsa), ndi kuti
mitima Yanu ikhazikike ndi
chimenecho. Ndipo Palibe
chipulumutso (chothandiza) Koma
chimene chachokera kwa
Mulungu, Ndithu, Mulungu
Ngwamphamvu zoposa,
Ngwanzeru zakuya. x
1 (Ndime 10-11) Asilamu adapeza lonjezo lochoka kwa Mulungu lakuti
panthawi yankhondo adzawatumizira Angelo, pamenepo mitima ya Asilamu
Surat 8. Al-Anfal
Juzu 9
366
^ *>i
A JlijSll $jj~-
11. (Kumbukirani) pamene
anakugonetsani Tulo tomwe tidali
mtendere wochokera Kwa lye,
ndipo anavumbwitsa mvula painu
Yochokera kumitambo kuti
akuyeretseni Nayo (matupi anu)
ndikukuchotserani
Manong'onong'o a Satana,
ndikuipatsa Mphamvu mitima
yanu ndiponso Ndikulimbikitsa
mapazi anu (Pamchenga)
12. (Kumbukira ) pamene
Mbuye wako Anawauza angelo
Kuti: "Ine ndili pamodzi nanu
(Pokulimbikitsani ndi chithandizo
Changa). Alimbikitseni amene
Akhulupirira, ndipo ndidzathira
Mantha m' mitima mwa amene
Sadakhulupirire Mulungu.
Choncho Amenyeni m'mitu yawo,
ndi Kuwadula zala zawo. (Zimene
akugwirira zida)
13. Izi ndi chifukwa chakuti iwo
Anapikisana ndi Mulungu ndi
Mtumiki wake (iwo podziika mbali
Ina kusiya komwe kudali
o
jdakhazikika kotero kuti ena mwa iwo adadzilotera nakhala ndi Janaba.
Choncho panafunika kuti asambe, koma madzi panalibe. Ndipo mwadzidzidzi
mvula idawavumbwira ndipo adapeza madzi osamba ndi ena ogwira nawo
ntchito zina. Chigwa cha Badiri chidali chamchenga wokhawokha. Ndipo
mchenga umene udali kumbali ya Asilamu udali wosayendeka. Munthu akati
ayende, mapazi amangozama. Tero pamene mvulayo idavumbwa, mchengawo
udagwirana nkukhala woyendeka. Zitatero Asilamu zidawayendera bwino.
Koma kumbali ya Amshirikina kudali matope okhaokha. Choncho sadathe
kuyenda mwachangu. Umo ndimomwe chifundo cha Mulungu chidalili pa
Asilamu.
Surat 8. Al-Anfal
Juzu 9
367
* fr>i
A JUjSM «jj-<
Mulungu). Amene akupikisana ndi
Mulungu ndi Mtumiki Wake,
ndithu Mulungu ndi Wolanga
kwambiri (amalanga Ndi chilango
choopsa).
14. Chimenecho ndi chilango
(cha Mulungu E! Inu makuraishi)
choncho Chilaweni. Ndithu
osakhulupirira adzapeza Chilango
chamoto.
15. E inu amene
mwakhulupirira! (Choonadi)
pamene mukumana nawo
(Munkhondo) amene
sadakhulupirire Alikudza kwa inu
mwaunyinji Musawatembenuzire
misana kuthawa.
16. Ndipo amene
adzawatembenuzire msana
Kuthawa patsikulo-osati
Kutembenuka (kwa ndale) kofuna
kumenyana Kapena kukalowa
m'gulu (la Asilamu)- Ndiye kuti
adziitanira mkwiyo wochokera
Kwa Mulungu; ndipo malo ake ndi
ku Jahannama, Pamenepo ndi
pamalo poipa kubwererapo.
17. Inu simudawaphe (ndi
mphamvu zanu) Koma Mulungu
ndi Yemwe anawapha;
Siudawagende pamene udagenda
koma Mulungu ndi amene
anawagenda (Pofikitsa mchenga
m'maso mwawo, Wachita
©J&1IoIl&
Surat 8. Al-Anfal
Juzu 9
368
* *>i
A Jtfity *jj~>
zimenezi) kuti awachitire zabwino
Asilamu powapatsa dalitso
labwino lochokera Kwa lye.
Ndithu, Mulungu Ngwakumva,
Ngodziwa. ]
18. Izi akuchitirani (pakalipano)
Ndithudi Mulungu afooketsa ndale
Za osakhulupirira.
19. Ngati mwakhala mukufuna
chiweruzo (Pogwirira nsalu
yovindikira ka'aba kuti
Mupambane pankhondo),
chiweruzo Chakudzerani
(chokomera Asilamu). Ndipo
Ngati musiya (kuwazunza
okhulupirira Kapena kusiya
kunyoza Mulungu) Chikhala
chinthu chabwino kwa inu. Koma
ngati mubwereza (kuwaputa)
nafenso Tidzabwereza
(kukulangani). Gulu Lanu
lankhondo silikuthandizani kanthu
Ngakhale lichuluke chotani. Ndipo
Mulungu ali pamodzi ndi
okhulupirira.
20. E inu amene
mwakhulupirira! Mverani
Mulungu ndi Mtumiki Wake,
<^$#^<toSS$
9 \'&Z'?\\»SX' *C< \9>J&* 9 \
Pamene nkhondo idayaka moto, Mtumiki (madalitso ndi Mtendere zikhale
naye) adatapa mchenga naufumbata m'manja mwake naupempherera. Kenako
adaumwaza kumbali ya adani. Ndipo mchengawo udalowa m'maso mwa
aliyense wa adaniwo.
Pankhondoyi anthu osakhulupirira Mulungu adali ambiri kuposa Asilamu.
Koma ngakhale zidali choncho, Asilamu adagonjetsa adaniwo kwathunthu.
Ambiri adaphedwa, ndipo ambirinso adagwidwa monga akaidi.
Surat 8. Al-Anfal
Juzu 9
369
* frjJH
A JUijSfi 3jj~-
Ndipo musamtembenukire kumbali
pamene Inu mukumva. 1
21. Ndipo musakhale monga aja
achinyengo Omwe akunena:
"Tamva (choonadi Ndipo
tachisunga)", pomwe iwo sakumva
(Kumva kochigonjera).
22. Ndithu nyama zoipitsitsa
pamaso pa Mulungu Ndi agonthi,
abubu amene alibe nzeru, (Omwe
ndi Amshirikina ndi anthu
Achinyengo).
23. Ndipo Mulungu akadadziwa
mwa iwo (Ndikudziwa kwake
kopanda chiyambi); Kuti muli
ubwino (pakuwamveretsa Qur'an
Ndi kuwazindikiritsa)
akadawamveretsa. (Koma
chikhalidwe chawo chili
chamtundu umenewo) Ndipo
ngakhale akadawamveretsa
(Qur'an Ndikuwazindikiritsa)
akadatembenuka M'mbuyo uku
akunyoza (chifukwa chakugonjera
Zilakolako zawo).
24. E inu amene
mwakhulupirira (choonadi)!
Muvomereni Mulungu (pazimene
Akukulamulani) ndiponso
muvomereni Mtumiki wake
1 (Ndime 20-23). Ndime izi zikufotokoza kuipa kwa yemwe wamvera ulaliki ndi
malangizo abwino koma naunyoza, osaugwiritsa ntchito. Ndithudi, anthu
otere ndi anthu oipitsitsa. Koma chofunika nchakuti tikamva mawu a Mulungu
tigwiritse ntchito pamoyo wathu onse.
Surat 8. Al-Anfal
Juzu 9
370
* ftjA-i
A jUiSfl 3jj-*»
pamene akukuitanirani ku chimene
Chingakupatseni moyo (wabwino
wa padziko Lapansi ndi tsiku
lomaliza). Ndipo dziwani Kuti
Mulungu amakhala pakati pa
munthu Ndi moyo wake
(amautembenula mmene
Akufunira). Ndipo dziwani kuti
kwa lye Mudzasonkhanitsidwa. (
25, Ndipo muope mazunzo (a
Mulungu a Pano padziko lapansi)
omwe sangagwere Okhawo amene
adzichitira zoipa mwa Inu (koma
adzawagweranso amene akusiya
Kuletsa zoipa) ndipo dziwani kuti
Mulungu Ngolanga kwambiri. 2
26. Ndipo kumbukirani (inu
Asilamu) Pamene mudali
owerengeka, ochepa, Onyozeka
m'dziko. Mumakhala moopa
Anthu kuti angakufwambeni, koma
Anakupatsani pamalo pabwino
pokhala Nakulimbikitsani ndi
chipulumutso Chake,
©&##j®JfJfe'
© v-v-
&*H5Jai»
5&5Z \f^^%%
1 Mu aya iyi akutiuza kuti chimene Mtumiki akutiitanira nchabwino kwa anthu
onse, kuyambira padziko lapansi mpaka pa tsiku lachimaliziro. Ndiponso
tikuuzidwa kuti Mulungu Ngokhoza chilichonse. Akhoza kuchita chilichonse pa
akapolo Ake palibe chimene chingalephereke. Koma ngakhale zili tero,
Mulungu akuzimvera chisoni zolengedwa Zake.
2 Mu aya iyi anthu olungama akuwauza kuti asalekerere anthu oipa pamene
akuchita zoipa zawo popanda kuwaletsa chifukwa chakuti, chilango
chapadziko lapansi chikadza chimagwera oipa ndi abwino omwe, ngakhale
kuti abwinowo adzapeza zabwino patsiku lachimaliziro. Koma zilango
zapadziko lapansi zimakhala za onse. Nchimodzimodzinso ndi madalitso,
akadza amakhudza anthu onse. Choncho, nkofunika kwa anthu olungama
kuletsa anthu osalungama kuchita zoipa, ndi kuwalangiza kuchita zabwino.
Surat 8. Al-Anfal
Juzu 9
371
S frj*-i
A J laity Sjj-"
Nakuninkhani zinthu zabwino kuti
muyamike (Mulungu). 1
27. E inu amene
mwakhulupirira! Musachitire
Mulungu ndi Mtumiki (Wake)
chinyengo (Pa kutsata zimene
mwaletsed wa) .Ndipo
Musazichitire chinyengo zimene
Mwakhulupirika nazo uku
mukudziwa (Kuti kutero
ndikulakwa).
28. Ndipo dziwani kuti chuma
chanu ndi ana Anu ndimayesero
(oyesedwa ndi Mulungu Kuti aone
mmene mungagwiritsire nazo
Ntchito). Ndi kuti kwa Mulungu
Kuli malipiro akulu.
29. E inu amene
mwakhulupirira! Ngati Muopa
Mulungu, adzakuzindikiritsani
Chilekanitso (cholekanitsa pakati pa
Choonadi ndi chachabe) Ndiponso
akufafanizirani zoipa zanu ndi
Kukukhululukirani. Ndipo Mulungu
ndi Mwini ubwino waukulu. 2
30. Ndipo (kumbukira) pamene
omwe sadakhulupirire
Amakuchitira chiwembu kuti
akunjate, Kapena akuphe kapena
y 9 "
®&j$&&m^
1 Anthu akakhala mumtendere nkofunika kumakumbukira zanthawi yomwe
adali m'masautso kuti amuyamike Mulungu pamtendere umene wawapatsawo
ndi kupewa machimo chtfukwa chakuti palibe chomwe chimachotsa mtendere
choposa machimo ndikusamuyamika mwini mtenderewo.
2 Munthu ngati akuopa Mulungu moona mtima, ndiye kuti Mulungu amutsekulira
makomo amadalitso pano padziko lapansi ndi pa tsiku la chimaliziro.
Surat 8. Al-Anfal
Juzu 9
372
* *>i
A JUkSM Ojj**>
akutulutse (M'dziko lawo la
Makka mwachipongwe). Ndipo
amachita chiwembu, naye
Mulungu anawononga chiwembu
chawocho. Ndipo Mulungu
ndiwokhoza koposa Poononga
ziwembu (za anthu oipa). 1
31. Ndipo (Akuraishi)
zikawerengedwa Aya zathu kwa
iwo amanena: "Tidazimva (izi
kale). Tikadafuna Tikadanena
zonga izi. Izi sikanthu Koma
ndinthano za anthu akale
32. Ndipo (kumbukira) pamene
adati: "E Inu Mulungu! Ngati ichi
(Chimene wadza nacho
MuhammadjSAW}) Chili
choonadi chochokera kwa Inu,
Tivumbwitsireni mvula ya miyala
Yochokera mlengalenga, kapena
Mutibweretsere chilango chowawa
Kwambiri."
Apa pakutchulidwa ziwembu za Akuraishi zomwe adamchitira Mtumiki
(Madalitso ndi mtendere zikhale naye) asanasamuke ku Makka. Iwo
adasonkhana m'nyumba yochitiramo upo nayamba kukambirana zachomwe
angachite naye Mneneri Muhammad, chimene chingamuonongeretu. Ena
anapereka maganizo akuti akamponye m'ndende konko ku Makka popanda
kumpatsa chakudya. Kapena ampatse chakudya chochepa kwambiri kufikira
afe ndi njala. Ndipo ena adati koma amtseke maso ndi milomo ndi kumnjata
goli m'manja kenako kumkweza pangamira nkukamtaya kuchipululu
chamchenga kuti akafere konko.
Ena amapereka ganizo loti asankhe anyamata ochokera m'mafuko amfulu kuti
onse pamodzi akammenye ndi kumupha. Ganizoli ndi lomwe anavomerezana.
Koma usiku omwe adapangana kuti amuphe, ndi umene Mtumiki (madalitso
ndi mtendere zikhale naye) adasamuka kunka ku Madina. potero adalephera
kumupha.
2 Aya iyi ikusonyeza kuti sadali kuchifuna choonadi, chilungamo ndi zabwino
zomwe adadza nazo Mneneri Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale naye).
Surat 8. Al-Anfal
Juzu 9
373
^ *>i
A jUity ejj-»
33. Koma Mulungu
sangawalange pomwe Iwe uli
nawo. Ndipo Mulungu
Sakadawalanga pomwe (ena mwa
Iwo) akupempha chikhululuko.
34. (Kodi iwo Akuraishi) ali
ndi chinthu Chanji (chabwino
chimene) chingamuletse Mulungu
kuwalanga? Pomwe Iwo
Akuwatsekereza anthu kulowa mu
Msikiti Wopatulika. Iwo
sanayenere kukhala Ouyang'anira
(Msikitiwo). Palibe
angauyang'anire koma olungama,
Koma anthu ambiri sadziwa. ]
35. Ndipo mapemphero awo
panyumba Yopatulikayo sadali
kanthu, koma Kuyimba miluzi ndi
kuombam'manja. Choncho
(adauzidwa): "Lawani Chilango
chifukwa chakusakhulupirira
kwanu."
36. Ndithu osakhulupirira
akupereka chuma Chawo
(pankhondo yolimbana ndi
Asilamu) ndi cholinga choti aletse
Anthu kuyenda pa njira ya
Mulungu. Adzapitiriza kupereka
chumacho Kenako chidzakhala
chowadandaulitsa, Ndipo
adzagonjetsedwa. Ndipo omwe
^J^t S^** Obi (^fc Uj
1 M'chaka chachisanu nchlmodzi (6) chakusamuka, Mtumiki (Madalitso ndi
mtendere zikhale naye) pamodzi ndi omtsatira ake ochuluka zedi adapita ku
Makka ncholinga chokachita mapemphero a Umra. Koma Akuraishi adamuletsa
kulowa mumzinda wa Makka podziganizira kuti iwo ndiwo oyang'anira Kaaba.
Surat 8. Al-Anfal Juzu 10
374
\ • *>i
A JliiSlI Sjj--
Sanakhulupirire
adzasonkhanitsidwa ku
Jahannama.
37. Kuti Mulungu alekanitse
oipa ndi abwino Ndi kuti awayike
ena mwa oipawo pamwamba Pa
anzawo, potero nkuwaunjika
oipawo mulu Umodzi, kenako
nawaponya ku Jahannama. Iwowa
Ndi anthu otaika.
38. Nena kwa osakhulupirira
kuti: "Ngati asiya (Zochita zawo
zoipa), adzakhululukidwa Zimene
zidatsogola. Koma ngati abwereza
(Kuwazunza Asilamu, tiwalanga)
ndithudi njira Ya Mulungu yomwe
idachitika kwa anthu akale
inadutsa (Powalanga akasiya
kutsata malamulo a Mulungu).
39. Pitirizani kumenyana nawo
osakhulupirira Kufikira Shirik
hatha ndipo chipembedzo Chonse
chikhale cha Mulungu. Ndipo
Ngati asiya, ndithu, Mulungu
Ngoona Zomwe akuchita.
40. Koma ngati apitiriza
kunyoza kwawo, Dziwani kuti
Mulungu ndi Mtetezi wanu,
Mtetezi wokoma mtima koposa,
ndi Mthandizi wabwino.
41. Ndipo dziwani kuti
chilichonse Chimene mwapeza
monga chuma Cholanda
kunkhondo,chigawo chimodzi
\9}9)'« 9 iS?, '<* 9£\4,9fi<
ft. • 9 . • 1%" << \, * 9 J 9\\£'
)9 "&LI '9. '
Surat 8. Al-Anfal Juzu 10
375
\ * *>i
A JUL»S?t tjj~>
Mwa zigawo zisanu ndi cha
Mulungu Ndi Mtumiki, ndi a
chibale(a Mtumiki), Amasiye,
masikini ndi munthu wapaulendo
(Amene asowedwa choyendera
paulendo. Tsatilani malamulowa)
ngatidi Mwakhulupirira Mulungu
(mwachoonadi) Ndi chimene
tachivumbulutsa kwa kapolo
Wathu pa tsiku lachilekanitso
(Lolekanitsa pakati Pachoona ndi
chabodza), tsiku Limene magulu
awiri adakumana (Tsiku la
nkhondo ya Badiri, gulu La
nkhondo la Asilamu ndi gulu La
nkhondo la osakhulupirira
(akafiri). Ndipo Mulungu
Ngokhoza kuchita Chilichonse.
42. (Kumbukirani) pamene
mudali mbali Yachigwa
yoyandikira (Mzinda wa Madina)
pomwe iwo (ankhondo a
Chikuraishi) adali mbali yakutali
Yatsidya lina (la chigwacho)
pomwe Aulendo amalonda adali
chakumunsi Kwanu. Ngati
mukadapangana nthawi
Yokumanirana (kuti mukumane
nthawi Yakutiyakuti),
mukadasiyana posunga
Chipangano (chifukwa chakuopa
Kuchuluka kwa adani anuwo).
Koma (Mwakumana
mosayembekezera ndi Ankhondo
aadaniwo) kuti Mulungu
Surat 8. AI-Anfal Juzu 10
376 y * *>»
A jUity ojj-*
Akwaniritse chinthu chomwe
nchofunika Kuti chichitike kuti
awonongeke amene Waonongeka
(posankha kusakhulupirira). Ndi
umboni woonekera (umene
adaukana Kuutsata). ndi kuti
akhale ndi moyo Amene wakhala
ndi moyo (amene watsata Njira ya
Chisilamu) ndi umboninso
Woonekera. Ndithudi, Mulungu
Ngwakumva zonse, Ngodziwa
kwambiri. 1
1 M'ndime iyi mwatchulidwa gulu lankhondo la Asilamu ndi gulu lankhondo la
Akuraishi ndi aulendo a chuma chamalonda a Akuraishi. Akuraishi adavutitsa
Asilamu mu Mzinda wa Makka m'nyengo yazaka khumi ndi zitatu powalanda
zinthu zawo ndi kuwamenya ndi kuwapha kumene. Pambuyo pake Asilamu
adathawira ku Madina nkusiya chuma chawo chonse ku Makka. Chumacho
chidatengedwa ndi anthu osakhulupirira Mulungu a Chikuraishi. Ndipo
kuonjezera pazimenezi Akafiri (Akuraishi) adali kudza ku Madina usiku
kudzaononga zinthu zambiri, pambuyo pake nkuthawa. Ndipo mwa zomwe
adachita ndi monga kutentha nyumba ndi ziweto. Ankachitanso zifwamba
zambiri.
Patapita zaka khumi ndi zisanu, Asilamu akuvutitsidwabe, Mulungu
adawapatsa chilolezo kuti amenyane ndi Akafiriwo monga momwe iwo adali
kuwamenyera. Ndiponso kuti awalande chilichonse chimene Asilamu
angathe kulanda kuti abweze zinthu zawo zomwe adawalanda. Choncho
Mtumiki (Madalitso ndi Mtendere zikhale naye) adamva kuti pali ulendo wa
Akuraishi umene wanyamula chuma chambiri ndipo udzadutsa pafupi ndi
mzinda wa Madina. Tero, adawakhwirizira omtsatira ake (Maswahaba) kuti
apite pamodzi naye nkukauthira nkhondo uiendowo, nkuulanda chumacho.
Choncho anthu adamtsata okwana mazana atatu popanda kutenga zida
zaukali zankhondo poti sadalinge kukamenya nkhondo yeniyeni koma
adalinga kukalanda chumacho basi, chomwe chidali m'manja mwa anthu
ochepa apaulendo; ndipo sadalinge kukawapha. Koma wotsogolera ulendo
wamalondawo, mwamwayi adamva kuti Mtumiki ndi omtsatira ake
akumufunafuna kuti amulande chumacho. Pompo adasintha njira natsata njira
ina yomwe siinkayendedwa kuti asakumane ndi Mtumiki.
Ndipo anatuma mthenga ku Makka kuti akawauze anthu am'Makka kuti iwo
anthu amalonda athiridwa nkhondo. Akuraishi ku Makka atamva nkhani iyi,
adasangalala. Adaona kuti apeza mwayi womumaliziratu Mtumiki Muhammad
(SAW) ndi omtsatira ake. Choncho adatuluka atakonzeka bwinobwino
zankhondo. Osati momwe Mtumiki ndi omtsatira ake adakonzekera.
Surat 8. Al-Anfal Juzu 10
377 I > • >>»
A JUj^i 5jj^
43. (Kumbukira) pamene
Mulungu adakuonetsa Iwo
kumaloto kwako kuti ngochepa
(Pachiwerengero chawo potero
udalimba Mtima zakukumana
nawo) Akanakuonetsa Iwo kuti
ngambiri pachiwerengero chawo;
Inu (Asilamu) mukadachita
mantha (mukanataya Mtima) ndipo
mukanakangana pachinthucho.
(Ena akanafuna kumenyana nawo
pamene ena Akanakana), koma
Mulungu anakutetezani
(Kuzimenezo). Ndithu, lye
Ngodziwa kwambiri Za m'mitima.
44. Ndipo (kumbukirani)
pamene anakuonetsani Iwo
m'maso mwanu, pamene
munakumana Nawo kuti Iwo ndi
ochepa, (owerengeka, kuti
Mukhale ndi chidwi chomenyana
nawo), ndiponso Anakuchepetsani
kwambiri m'maso mwawo (Kuti
iwo aone kuti nkosafunika
kukonzekera Kwambiri chifukwa
Mtumiki ndi omtsatira ake sadadziwe kuti aulendo amene iwo adali
kuwadikirira awadutsa kale, ndi kuti gulu lalikulu lankhondo la Akuraishi
likuwadzera kudzawathira nkhondo, ndipo lafika kale pafupi nawo Adadziwa
za nkhaniyo pomwe iwo (Mtumiki ndi gulu lake) adali kutali ndi mzinda wawo
wa Madina. Ndipo nkhaniyi itadziwika kwa omtsatira ake, padabuka
mkangano pakati pawo. Ena adali ndi maganizo akuti alithawe gulu lankhondo
la Akuraishiwo, nkupitiriza kutsatira gulu lamalonda lija, pakuti adali ndi
chitsimikizo chonse kuti akawagonjetsa amalondawo. Koma gulu lankhondo la
Akuraishi adalibe nalo chiyembekezo choligonjetsa naona kuti sikwabwino
kudziika okha pachionongeko. Koma mwamwayi adakumana nalo gulu
lankhondo la Akuraishi mosayembekezera pomwe aulendo wa malonda aja
adali kutali nawo.
Tero ili ndilo tanthauzo la aya ya 42.
Surat 8. Al-Anfal Juzu 10
378
\ • *>i
A JUj^M 5jj--
chakuchepa kwa Omenyana
nawowo) kuti Mulungu
Akwaniritse chimene adalamula
kuchitika. Kwa Mulungu Yekha
ndiko kobwerera zinthu zonse.
45. E inu amene
mwakhulupirira! Pamene
Mukumana ndi gulu (la
osakhulupirira), Mulimbe mtima,
ndipo tamandani Mulungu
Kwambiri kuti mupambane.
46. Ndipo mumvereni Mulungu
ndi Mtumiki Wake, musakangane
(kuopera kuti) Mungachite mantha
(ndi kutaya Mtima) Ndikuchoka
mphamvu zanu. Koma Pitirizani
kupirira. Ndithudi, Mulungu Ali
pamodzi ndi anthu opirira.
47. Ndipo musakhale ngati
anthu amene anatuluka M'nyumba
zawo modzikweza ndi
Modzionetsera kwa anthu,
ndikuwaletsa Anthu kuyenda
panjira ya Mulungu. Koma
Mulungu ndi Wodziwa kwambiri
Zimene akuchita.
48. Ndipo (kumbukira) pamene
Satana Adawakometsera zochita
zawo zoipa (Aja osakhulupirira)
nati: "Lero Palibe aliyense mwa
anthu amene Angakugonjetseni,
ndipo ine ndine Mtetezi wanu".
Koma pamene magulu Awiri
ankhondo anaonana (anakumana
Surat 8. Al-Anfal Juzu 10
379
S * *>i
A JUi^l bjj~*
Pamaso ndi pamaso) Satana
anabwerera Pambuyo (kuthawa)
nati: "Ine Ndikudzipatula mwa inu.
Ndithu, ine Ndikuona zimene inu
simukuziona.Ndithu ine ndikuopa
Mulungu." Ndipo Mulungu
Ngwaukali polanga.
49. (Kumbukirani) pamene
achiphamaso Ndi amene ali ndi
matenda M'mitima mwawo
amanena: "Anthu awa
Chipembedzo chawo (cha
chisilamu) Chawanyenga."
Komatu amene akuyadzamira Kwa
Mulungu ndithudi Mulungu
Ngwamphamvu zoposa,
Ngwanzeru Zakuya.
50. Ndipo ukadaona angelo
pamene akuchotsa Miyoyo ya
anthu amene sadakhulupirire (Pa
imfa yawo) uku akumenya
kunkhope Zawo ndi kumisana
yawo (uku akunena) "Lawani
chilango chamoto".
51. "Izo ndi chifukwa cha
(machimo) Amene manja anu
anawatsogoza, Ndipo Mulungu sali
opondereza Akapolo Ake." 1
a<^;£Wa#u
-T "\\ ' \ K ' \ 92 * '*'
1 Mizjmu ya osakhulupirira ikamachotsedwa, imachotsedwa mwamasautso
kwambiri. Koma amene ali pafupi ndi wakufayo saona zimenezi pakuti ife
sititha kuiona mizimu ndi zonse zokhudzana ndi mizimu. Ife timangoona thupi
lawakufayo poliona thupilo likuzunzika.Kuzunzika kwa mzimu sindiko kuzunzika
kwathupi. Choncho kuzunzika komwe kukunenedwa apa nkuzunzika kwa
mzimu komwe kumaapeza anthu osakhulupirira. Komatu masautso athupi
amene amawapeza anthu ena panthawi yaimfa pophuphaphupha, sasonyeza
kusalungama kwa munthuyo. Koma amasonyeza mphamvu zomwe zidali
Surat 8. Al-Anfal Juzu 10
380
\ • ftjA-i
A jUity ojj-*
52. (Khalidwe lawo awa lili )
ngati khalidwe la Anthu a Farawo
ndi omwe adalipo Patsogolo pawo.
Anazikana aya Za Mulungu,
choncho Mulungu Anawalanga
chifukwa cha machimo A wo.
Ndithudi Mulungu
Ngwamphamvu, Wolanga moopsa.
53. Izo, (posawadzera miriri
yotere) Nchifukwa chakuti
Mulungu sasintha Chisomo chake
chimene wachipereka Kwa anthu
mpaka anthuwo asinthe Okha
zomwe zili m'mitima mwawo,
(Posiya kuthokoza Mulungu
nayamba Kuyenda m'njira
zolakwira Mulungu). Ndithu
Mulungu Ngwakumva Ngodziwa
chilichonse.
54. (Khalidwe lawo lili) ngati
khalidwe La anthu a Farawo ndi
omwe adalipo Patsogolo pawo.
Adakana Aya za Mbuye wawo.
Choncho, tidawaononga Chifukwa
cha machimo awo, ndipo
Tidawamiza anthu a Farawo.
Ndipo Onse adali ochita zoipa.
55. Ndithu, nyama zoipitsitsa
kwa Mulungu ndi Amene
sadakhulupirire (Amamkana
m'thupi mwamunthuyo. Sizikhudzana ndi kulungama kwake ndi kusalungama
kwake. Mungawaone anthu oipa akufa ndi imfa yodekha pomwe amene adali
abwino akufa ndi imfa yophuphaphupha ndikudzimenyamenya. Choncho
kuphuphaphupha kumeneko nkwathupi chifukwa chokhala ndi mphamvu,
Choncho tisadodome pomwe tiona munthu wabwino akuphuphaphupha.
Siirat 8. Al-Anfal Juzu 10
381
> * tjtr\
A JUi/sll 3j^»
Mulungu ngakhale choonadi
Akuchidziwa bwinobwino),
choncho Iwo sakhulupirira
56. Omwe unapangana nawo
chipangano Kenako naaswa
chipangano chawo Panthawi
iliyonse (imene mwapangana)
Ndiponso iwo saopa Mulungu.
57. Choncho, ngati uwapeza
kunkhondo, (Menyana nawo),
uwabalalitse (kuti Likhale
phunziro kwa) amene ali Pambuyo
pawo kuti iwo azindikire.
58. Ngati uopa kusakhulupirika
kwa Anthu (omwe unapangana
nawo Chipangano), atayire
(chipangano Chawocho),
mwachilungamo; Ndithu Mulungu
Sakonda (anthu) osakhulupirika.
59. Ndipo (anthu) amene
sadakhulupirire Asaganize kuti
ampitirira (Mulungu Kotero kuti
sachita kanthu ndi iwo) Ai, iwo
sangamulepheretse Mulungu
(Chimene akufuna kuchita pa iwo).
60. Ndipo akonzekereni mmene
mungathere (Zomenyera
nkhondo) ndi mphamvu zanu
(Zonse), ndiponso poikiratu
mahatchi odikira Nkhondo kuti
muwaopseze nazo adani A
Mulungu ndi adani anu (amene
Mukuwadziwa) ndiponso (ndi )
Ena omwe (inu) simukuwadziwa.
Surat 8. Al-Anfal Juzu 10
382
> • *j*-1
A Jlflity 0jj~*
Koma Mulungu akuwadziwa.
Ndipo Chilichonse mungapereke
pa njira Ya Mulungu
chidzalipidwa kwa inu Modzadza
Ndipo simuzaponderezedwa.
61. Ndipo ngati (awo adani)
apendekera Kumbali yokhalirana
mwa mtendere, Nawenso
pendekera (kumbaliyo) Ukatero
yadzamira kwa Mulungu. Ndithudi
lye Ngwakumva, Ngodziwa.
62. Ngati afuna kukunyenga
pachimvanochi, Ndithudi,
Mulungu akukwanira kwa Iwe
(kukuteteza). lye ndi Yemwe
anakuthangata Ndi chipulumutso
chake ndi Okhulupirira.
63. Ndipo (Mulungu)
analuzanitsa pakati Pamitima yawo
(poika chikondi pakati Pawo).
Ngati ukanapereka zonse za
M'dziko lapansi (ncholinga choti
uwaluzanitse Mitima yawo mwa
iwe wekha) sukadatha Kuluzanitsa
pakati pa mitima yawo. Koma
Mulungu adaluzanitsa pakati
Pawo. Ndithu, lye Ngwamphamvu
Zoposa Ngwanzeru zakuya.
64. E iwe Mneneri ! Mulungu
Akukwanira kwa iwe kukuteteza
pamodzi Ndi amene akutsata (iwe)
mwa Okhulupirira.
65. E iwe Mneneri! Alimbikitse
okhulupirira Kupita kunkhondo.
b J$tf<m#6W
Surat 8. Al-Anfal Juzu 10
383
\ * *>i
A Jl&Sh *jj~*
Ngati Mwa inu muli anthu
Makumi awiri olimba Mtima
(ndiye kuti) adzawagonjetsa
Mazana awiri (200) (a mwa anthu
Osakhulupirira). Ngati mwa inu
muli anthu Zana limodzi (100)
olimba mtima (Ndiye kuti)
adzagonjetsa chikwi Chimodzi
(1,000) cha anthu omwe
Sadakhulupirire, chifukwa chakuti
Iwo ndi anthu osazindikira.
66. Tsopano Mulungu
wakupeputsirani (Lamulo
lovutali), ndipo wadziwa kuti muli
Kufooka mwa inu. Choncho ngati
mwa Inu muli anthu zana limodzi
olimba Mtima adzagonjetsa
mazana awiri. Ngati alipo mwa inu
chikwi chimodzi, Adzagonjetsa
zikwi ziwiri, mwachilolezo Cha
Mulungu. Mulungu ali Pamodzi
ndi opirira.
67. Sichoyenera kwa Mneneri
kukhala ndi Akayidi mpaka
amenye nkhondo (Kwambiri) ndi
kugonjetseratu maiko Molimba
(ndi pamene atha kukhala Ndi
akayidi). Mukufuna zinthu za
M'dziko pomwe Mulungu akufuna
(Mupeze mphoto ya) tsiku
lomaliza Ndipo Mulungu
Ngwamphamvu zoposa
Ngwanzeru zakuya.
68. Pakadapanda lamulo la
Mulungu limene Linatsogolera
^s&^i<S3$i
Surat 8. Al-Anfal Juzu 10
384
\ • *>i
A jUi^l 5jj-*
kale, chilango Chachikulu
chikanakugwerani, Chifukwa cha
zimene munatenga (ku-Nkhondo
ya Badri).
69. Tsopano idyani chuma
chimene mwalanda Pankhondo
(chomwe chili) chololedwa,
chabwino, Ndipo pitirizani kuopa
Mulungu. Ndithu, Mulungu
Ngokhululuka, Ngwachisoni.
70. E iwe Mneneri (SAW) !Uza
akaidi apankhondo Amene ali
m'manja mwanu kuti ngati
Mulungu aona chabwino
chilichonse M'mitima mwanu,
adzakupatsani Zoposa zimene
mwalandidwa ndipo
Adzakukhululukirani; Mulungu
Ngokhululuka Ngwachisoni.
71. Ngati akufuna kukuchitirani
chinyengo (Chinyengo chawo
sichiphula kanthu Pa iwe), ndithu
anamuchitirapo kale Mulungu
chinyengo (chifukwa
Chakusakhulupirira kwawo).
Choncho Anakupatsa mphamvu
zowagonjetsera I wo. Ndipo
Mulungu Ngodziwa, Ngwanzeru
zakuya.
72. Ndithu anthu amene
anakhulupirira nasamuka Kwawo
ndi kumenyana pa njira ya
Mulungu ndi chuma chawo ndi
moyo Wawo; ndiponso amene
^^^^V^
Surat 8. Al-Anfal Juzu 10
385 I > • *>>
A JtfiSlI ijj**>
anawalandira (iwo) Ndikuwapatsa
malo ndikuwathandiza, Awa ndi
abale otchinjirizana Wina ndi
mnzake. Ndipo anthu amene
Akhulupirira koma nasiya
kusamuka (Kudza ku Madina),
palibe udindo Pa inu wakuwateteza
kufikira nawonso Atasamuka
(kudza ku Madina). Ngati
Atakupemphani chithandizo
chachipembedzo Athandizeni,
kupatula (akaputana Ndi anthu)
amene pakati panu ndi iwo Pali
chipangano, (pamenepo
musawathandize Pomenyana ndi
osakhulupirirawo Omwe muli
nawo ndi chipangano). Ndipo
Mulungu Ngowoona zomwe
muchita.
73. Ndipo anthu amene
sadakhulupirire (Mulungu)
amatetezana okha Ndikukhala
abwenzi pakati pawo. Ngati
nanunso simuchita izi, Padzakhala
chisokonezo m'dziko ndi
chionongeko chachikulu.
74. Amene akhulupirira
nasamuka, namenya Nkhondo
panjira ya Mulungu (Pamodzi
nanu),ndiponso amene
Anawalandira (osamukawo)
Nawapatsa malo ndikuwathandiza,
iwo Ndi omwe ali okhulupirira
Mwachoonadi. iwo adzapeza
chikhululuko ndi Zopatsidwa
zaulemu.
%,'J* 9 *
<&m
Surat 8. Al-Anfal Juzu 10
386
> • *j*-l
A JbiiSM djj~>
75. Ndipo aja akhulupirira
pambuyo pa "Amuhajirina" ndi
"Answari," nawonso Nasamukira;
(ku Madina kukakhala pamodzi
ndi Mtumiki ndi Asilamu anzawo),
namenyanso Nkhondo pamodzi
nanu, iwo ndi amene ali Mwainu.
Koma achibale chakubadwana,
ndi Amene ali oyenera
(kulowerana mmalo pachuma.
Zimenezo nzomwe zili) m'Buku la
Mulungu. Ndithudi, Mulungu
Ngodziwa chilichonse.
&
Surat 9. At-Taubah Juzu 10
387 > • *>» * *j=J» *jJ~>
SURAT AT-TAUBAH IX
Surat Tauba idavumbulutsidwa ku Madina m'chaka cha 9 cha
kusamuka. Ndipo Ali, mwana wa Abu Twalib adaitenga Surayi
kunka nayo ku Haji komwe kudali Asilamu. Ndipo adawerenga.
Mmenemo nkuti Abubakar Swidiki ndiye adali mtsogoleri
woyanga'nira mapemphero a Haji.
Surayi ili ndi aya (ndime)129. Ndipo yayamba nkufotokoza
za kudzipatula kwa Mulungu ku Amshirikina. Pachifukwa ichi
ikutchedwanso Surat Bara'at (kudzipatula). Ndipo kenako
yafotokoza za miyezi yopatulika ndi mapangano a Amshirikina,
kuti adali oyenera kuwakwaniritsa ngati iwo eni sadawaswe.
Ndipo woswa pangano ngoyenera kuthiridwa nkhondo.
Surayi yafotokoza kuti mutu wodziyandikitsa kwa Mulungu
ndiko kumkhulupirira lye. Chikhulupiriro sichingakhale
chokwanira pokhapokha okhulupirira akonde kwambiri
Mulungu ndi Mtumiki wake kuposa china chilichose. Mulungu
wafotokozanso kuti kunyadira mphamvu kumalepheretsa
kupambana pankhondo, monga momwe zidawachitikira
Asilamu pankhondo ya Hunain. Ndipo m'Sura iyi, Amshirikina
aletsedwa kulowa mu Msikiti wopatulika umene uli mu Mzinda
wa Makka; chifukwa iwo ndi nyasi. Msurayi mulinso lamulo
lomenyana nawo nkhondo Ayuda ndi Akhristu kufikira
atapereka msonkho. Ndipo msurayi afotokozanso za
chiwerengero cha miyezi yopatulika ndi kuti nkhondo ikabuka,
nkofunika kwa Asilamu onse kupita kunkhondo.
Msurayi afotokozanso makhalidwe a Asilamu ena omwe
Chisilamu chawo chidali chachiphamaso; akauzidwa zopita
kunkhondo adali kukana ndipo adalinso kulimbikitsa anzawo
kuti asapiteko.
Msuramu mulinso lamulo lakuti Munafiku akamwalira,
Mtumiki asampempherere. Ndipo Surayi yafotokoza za
chikhalidwe cha anthu kumbali ya chikhulupiriro ndi za msikiti
Surat 9. At-Taubah Juzu 10
388
\ * *>i
S 4*f&\ 3jj-o
womwe Amunafikina adamanga n'cholinga choti awagawe
Asilamu pagulu lawo. Kenako Mulungu wafotokozanso za
makhalidwe a anthu okhulupirira Chauta omwe ali oona
pachikhulupiriro chawo, ndi kulandira kulapa kwa anthu omwe
adatsalira mu Mzinda wa Madina Mtumiki atapita kunkhondo.
Surayi yatsiriza nkunenetsa kuti Mulungu adasankha
Muhammad (SAW) kuti akhale Mthenga wachifundo kwa anthu
ake , ndi kuti Mulungu adzamsunga ngati anthu atamuukira.
Surat 9. At-Taubah Juzu 10
389
\ • *>»
^ ijjsii 0jj-»)
Surat At-Taubah IX
1. Uku ndikudzipatula
kochokera kwa Mulungu ndi
Mtumiki wake Ku (mapanganowa)
amene mudapangana nawo
(Kenako nkuswa mapangano
awowo) Am'gulu la Amshirikina. 1
2. (Auze Amshirikina kuti):
Yendani padziko Miyezi inayi
basi. (pambuyo pake Sipadzakhala
chitetezo pakati pawo Ndi ife).
Ndipo dziwani kuti inu
Simungathe kumpambana
Mulungu. Ndipo Mulungu
Ngosambula osakhulupirira.
3. Ndipo uku ndi kulengeza
kochokera Kwa Mulungu ndi
Mtumiki Wake kwa Anthu pa tsiku
la Haji Yaikulu kuti Ndithu,
Mulungu ndi Mtumiki Wake
Adzichotsa m'mapangano a
Amshirikina (Omwe ali
achinyengo). Choncho, ngati
Mulapa ndibwino kwa inu; ndipo
ngati Mutembenuka ndi kunyoza,
tsu 'w<\*9" ii ' "L't^y
1 Ndime 1-2. Omasulila Qur'an adati Arabu adali kuswa mapangano amene
adamanga pamodzi ndi Mtumiki wa Mulungu. Potero, Mulungu adalamula
Mtumiki wake kuti awaponyere mapangano awo. Choncho, Mtumiki adatuma
Abubakari kukhala mtsogoleri wa anthu kumapemphero a Haji. Ndipo
adamtsatanso Ali kumeneko ndi nkhani yokhayokhayo kuti akawawerengere
anthu kuti Mulungu ndi Mtumiki wake atulukamo m'mapangano okhalirana
mwamtendere ndi Amshirikina sadzaloledwa kuyandikira Nyumba Yopatulika
chaka chotsatiracho, ndikutinso sadzaloledwa kuzungulira Nyumba
yopatulikayo uku ali maliseche.
Surat 9. At-Taubah Juzu 10
390
\ • frj*-i
^ hy6\ $jj-*>
dziwani Kuti inu
simungamulepheretse Mulungu.
Ndipo auze za chilango chowawa
Amene sadakhulupirire.
4. Kupatula ena amene
mudapangana nawo Mapangano
mwa Amshirikina, (omwe
Adasunga mapangano awo),
kenako sadapungule Chilichonse
ndipo sadathandize Aliyense pa
inu, akwaniritseni Mapangano awo
mpaka m'nyengo yawo. Ndithu,
Mulungu akukonda amene
Akumuopa (ndi kusunga
mapangano).
5. Ndipo miyezi yopatulika
ikatha (Yomwe njoletsedwa
kuchitamo Nkhondo), apheni
Amshirikina Paliponse pamene
mwawapeza (Menyanani nawo),
ndipo agwireni (Monga momwe
iwo akukuchitirani). Ndipo
azungulireni ndi kuwakhalira Pa
njira zonse. Koma akalapa
Nayamba kupemphera Swala,
Ndikupereka chopereka (zakat),
ilekeni Njira yawoyo (asiyeni).
Ndithu, Mulungu Ngokhululuka
kwambiri, Ngwachisoni.
6. Ndipo ngati mmodzi wa
Amshirikina Atakupempha
chitetezo (kuti amvere Mawu a
Mulungu), mtetezeni kuti amve
Mawu a Mulungu. Kenako (ngati
Surat 9. At-Taubah Juzu 10 I 391 I \ . *>
^ hjs}\ djf*t
Sadakhutitsidwe nawo), mpititseni
Kumalo kwake mwamtendere
(ngati Safuna kulowa
m'Chisilamu). Izi Nchifukwa
chakuti iwo ndi anthu Osadziwa.
7. Chingakhalepo bwanji
chipangano Pakati pa Amshirikina
(oswa Mapangano nthawi ndi
nthawi) ndi Mulungu ndi Mthenga
Wake, kupatula Okhawo amene
mudapangana nawo Mapangano pa
Msikiti Wopatulika? (Amene
adakwaniritsa mapangano awo).
Ngati iwo akupitiriza kulungama
(Posunga mapanganowo) kwa inu,
Nanunso pitirizani kulungama kwa
Iwo. Ndithu, Mulungu akukonda
amene akumuopa.
8. (Kodi inu ndiye osunga
malonjezo?) Bwanji? Pomwe iwo
akakhala ndi Mphamvu pa inu
sakusungirani chibale Kapena
pangano. Amakusangalatsani Ndi
pakamwa pawo pomwe mitima
Yawo ikukana (kukukondani).
Ndipo Ambiri aiwo ngoukira
malamulo a Mulungu. l
9. Asinthanitsa aya za Mulungu
(ndi zinthu Zadziko lapansi) ndi
mtengo wochepa, Ndipo
atsekereza (anthu) kunjira Yake.
" A"\X JO. »WAS
(^^^J^^ZfOsofc
X'^tswt
Mulungu akuti kodi mungapangane nawo mapangano anthu oti akapeza
mwawi wokugonjetsani inu sasunga chibale chomwe chidali pakati panu
ngakhale pangano? Iwo amakunenerani mawu otsekemera ngati uchi pomwe
mitima yawo ndi yodzadzidwa ndi mkwiyo ndi inu.
Surat 9. At-Taubah Juzu 10
392
^ • *>i
^ fajd\ &jy~*
Ndithu, nzoipa kwabasi zomwe
Iwo akhala akuchita.
10. Sasunga chibale pa Msilamu
ngakhale Pangano. A wo ndiwo
Opyola malire.
11. Koma ngati alapa nayamba
kupemphera Swala ndikupereka
chopereka (zakaat), Ndiye kuti ndi
abale anu pa chipembedzo. Ndipo
tikuzifotokoza ayazi (mwabwino)
Kwa anthu odziwa.
12. Ndipo ngati aswa
malumbiro awo Pambuyo
pomanga chipangano Chawo, ndi
kuyamba kutukwana Chipembedzo
chanu, menyanani nawo Atsogoleri
akusakhulupirira. Ndithu, iwo
alibe Mapangano, (sasunga
mapangano. Menyanani nawo) kuti
iwo aleke (Machitidwe awo oipa).
13. Kodi nchotani kuti
musamenyane Nawo anthu omwe
aswa malonjezo Awo, natsimikiza
kumtulutsa (Kumpirikitsa mu
Mzinda wa Makka, Kapena
kumupha) Mtumiki? Iwo ndi
Amene adayamba kukuputani
Pachiyambi nanga mukuwaopa
chotani? Mulungu ndiye wofunika
kumuopa, ngati Inu mulidi
okhulupirira.
14. Menyanani nao; Mulungu
awalanga Kupyolera m'manja anu,
ndipo Awasambula ndi
©/
• 9\*9' \9\
'U.
S&&T
Surat 9. At-Taubah Juzu 10
393
> • i£\
^ i>jjl Ojj^d
kukupulumutsani Kwa iwo ndi
kuchiritsa kuwawidwa (komwe
Kudali) m'mitima mwa Asilamu
(Chifukwa cha masautso omwe
Adawapeza kwa iwo).
15. Ndi kuchotsa mkwiyo wa
m'mitima Mwawo (Asilamu). Ndi
kuti Mulungu Alandire kulapa
kwa amene wamfuna. Ndipo
Mulungu Ngodziwa, Ngwanzeru
zakuya.
16. Kodi mukuganiza kuti
mungosiidwa Chabe Mulungu
asanawaonetsere Poyera amene
amenyera chipembedzo Mwa inu
ndi amene sachita ubwenzi (Ndi
wina wake) kupatula Mulungu Ndi
Mtumiki wake ndi Asilamu?
Ndipo Mulungu Ngodziwa zonse
zimene Muchita.
17. Nkosayenera kwa
Amshirikina Kukhala (ndi udindo)
woyang'anira Misikiti ya Mulungu
pomwe iwo Akudzichitira okha
umboni kuti Ngosakhulupirira.
Awo (ndi omwe) Zochita zawo
zabwino zapita pachabe. Ndipo
iwo ku moto adzakhala Muyaya.
18. Ndithu, oyang'anira Misikiti
Ya Mulungu ndi kuiyendera ndi
Amene akhulupilira Mulungu ndi
Tsiku lomaliza, ndi kumapemphera
Swala ndi kupereka chopereka
(Zakaat) ndipo saopa aliyense
Surat 9. At-Taubah Juzu 10
394
1 • *><
^ <bjjl Sjj-**
koma Mulungu yekha. Choncho,
iwowo Ndi amene
akuyembekezeka Kukhala mwa
oongoka.
19. Kodi kumwetsa madzi
(anthu) Ochita Haji ndi kusunga
Msikiti Wopatulika mukukuyesa
kuti nkofanana Ndi yemwe
wakhulupirira Mulungu ndi tsiku
lomaliza, ndi Kumenyera nkhondo
pa njira Ya Mulungu? Sangakhale
ofanana Kwa Mulungu.Ndipo
Mulungu saongola anthu ochita
zolakwa.
20. Amene akhulupirira, ndi
kusamuka, Ndi kumenya nkhondo
pa njira ya Mulungu ndi chuma
chawo ndi Matupi awo, ali ndi
ulemerero Waukulu kwa Mulungu.
Iwowo ndiwo opambana.
21. Mbuye wawo akuwauza
nkhani yabwino Ya chifundo
chochokera kwa lye, ndi Chiyanjo
(Chake) ndi minda Yomwe mkati
mwake adzapezamo Mtendere
wamuyaya:
22. Adzakhala m'menemo
muyaya. Ndithu Mulungu ali nawo
Malipiro akulu.
23. E inu amene
mwakhulupirira! Musawachite
makolo Anu ndi abale anu kukhala
Atetezi anu ngati (iwo) akukonda
Kusakhulupirira Mulungu m'malo
Surat 9. At-Taubah Juzu 10
395 I > • *j*-i
^ hj£\ Qjj~*
Mokhulupirira (kukhala Asilamu).
Ndipo mwa inu amene ati
awasankhe Kukhala atetezi, otero
ndiwo adzichitira okha Zoipa.
24. Nena: "Ngati makolo ami,
ana Ami abale anu,akazi anu, ndi
Anansi anu ndi chuma chimene
Mwachipata,ndi malonda anu
amene Mukuopa kuti
angaonongeke, ndi Nyumba zanu
zimene mukuzikonda, (Ngati
zinthuzi zili) zokondeka Kwambiri
kwa inu kuposa Mulungu ndi
Mtumiki Wake ndi kuchita Jihadi
pa Njira Yake,choncho dikirani
kufikira Mulungu adzabwera ndi
lamulo lake (Lokukhaulitsani).
Ndipo Mulungu Satsogolera anthu
otuluka m'chilamulo (Chake).
25. Ndithu,Mulungu wakhala
akukupulumutsani (Kwa adani
anu) m'malo ambiri omenyanira
Nkhondo, ndi patsiku la Hunaini,
pamene Kudakunyengani
kuchuluka kwanu. Koma
sikudakuthandizeni chilichonse.
Ndipo dziko lidakupanani
ngakhale Kuti lidali lotambasuka
ndipo kenako Mudatembenukira
kumbuyo (kuthawa). 1
6^2&jftifcS!&
Apa Mulungu akuwakumbutsa Asilamu kuti wakhala akuwapulumutsa
m'nkhondo zosiyanasiyana, makamaka pankhondo ya Hunaini pamene
Asilamu adali kudzitama kuti sangagonjetsedwe chifukwa cha kuchuluka
kwawo. Koma kuchulukako sikudawathandize chilichonse. Nthawi zonse
chofunika kwa Msilamu nkudalira Mulungu. Asadalire mphamvu zake, chuma
kapena zina zotero.
Surat 9. At-Taubah Juzu 10
396
1 * >>i
^ AjjsJl ^jj- -
26. Kenaka Mulungu adatsitsa
mpumuloWake Kwa Mtumiki
Wake ndi kwa okhulupirira. Ndipo
adatsitsa asilikali ankhondo a
(Angelo) omwe simudawaone.
Ndipo Adawakhaulitsa
osakhulupirira. Imeneyo Ndiyo
mphoto ya osakhulupirira.
27. Ndipo pambuyo pa
izi,Mulungu Alandira kulapa
kwawo amene Wamfuna mwa
osakhulupirira (Powalowetsa
m' Chi silamu). Ndipo Mulungu
Ngokhululuka Ngwachisoni.
28. "E inu amene
mwakhulupirira! Ndithu,
Amushirikina ndi nyansi,
Choncho, asayandikire Msikiti
Wopatulika chikatha chaka
chaochi (cha 9 A.H), Ngati
mukuopa umphawi, posachedwa
Mulungu Akulemeretsani ndi
zabwino Zake akafuna. Ndithu,
Mulungu Ngodziwa zonse kwabasi
Ngwanzeru zakuya.
29. Menyanani ndi omwe
sakhulupirira mwa Mulungu ndi
tsiku lomaliza, omwenso Sakusiya
zoletsedwa zomwe Mulungu Ndi
Mtumiki Wake waletsa; omwenso
Satsatira chipembedzo choona
mwa amene Adapatsidwa mabuku.
(Menyanani nawo) Kufikira
apereke msonkho ndi manja awo
Uku ali odzichepetsa.
^^^s^mn
*
^*^&#i<K
Surat 9. At-Taubah Juzu 10
397
> • *>t
^ AjjsJt SjJ-*>
30. Ndipo Ayuda akunena kuti
Uzairi Ndi mwana wa Mulungu,
naonso Akhrisitu akunena kuti
Mesiya (Yesu) ndi Mwana wa
Mulungu. Awa ndi mawu amene
akunena Ndi pakamwa pawo
(popanda umboni Wochokera kwa
Mulungu); Akutsanzira zonena Za
omwe sadakhulupirire kale.
Mulungu Awaononge; Kodi iwo
akusokera chotani Kusiya
choonadi?
31. Ayesa ophunzira a za
chipembedzo Chawo ndi ansembe
awo kukhala Milungu kusiya Allah
(powatsata pazimene
Akuwalamula popanda umboni wa
Mulungu). (Amsandutsanso)
Mesiya (Yesu) mwana wa Maria
(Kukhala Mulungu); chikhalirecho
Sadalamulidwe china koma
kupembedza Mulungu Mmodzi.
Palibe wopembedzedwa
Mwachoonadi koma lye,
wapatukana ndi Zimene
akumphatikiza nazozo.
32. Akufuna kuzimitsa kuunika
kwa Mulungu (chisilamu) ndi
pakamwa Pawo; ndipo Mulungu
sadzalola Koma kukwaniritsa
kuunika Kwake Ngakhale kuti
osakhulupirira zikuwanyansa.
33. lye ndi Yemwe adatuma
Mtumiki Wake ndi ulangizi
ndiponso Chipembedzo choona
••
Surat 9. At-Taubah Juzu 10
398
1 • *J*-I
^ <UjsJl 3j^-*»
kuti achiwonetsere Pa zipembedzo
zonse,ngakhale atanyansidwa nazo
Amshirikina.
34. E inu amene
mwakhulupirira! Ndithu, ambiri
ophunzira a za Chipembedzo cha
Chiyuda ndi a za Chikhristu,
akudya chuma cha anthu
Mwachinyengo ndikuletsa anthu
ku Njira ya Mulungu. Ndipo
amene Akusonkhanitsa golide ndi
siliva Popanda kuzipereka pa njira
ya Mulungu, Auze nkhani ya
chilango chowawa.
35. Pa tsiku lomwe (chuma
chawo) Chidzatenthedwa ku moto
wa Jahannama, ndipo ndi
chumacho Zidzatenthedwa nkhope
zawo,nthiti Zawo ndi misana yawo
(ali kuwuzidwa Kuti): "Izi ndi zija
zomwe mudadzisungira Nokha.
Choncho lawani (chilango) Cha
zomwe mudali kuzisunga. 1
36. Ndithu,chiwerengero cha
miyezi Kwa Mulungu (pachaka),
ndi Miyezi khumi ndi iwiri
m'chilamulo Cha Mulungu
kuyambira tsiku lomwe Adalenga
thambo ndi nthaka. M'menemo
muli miyezi inayi Yopatulika. Ichi
ndicho chipembedzo Cha Mulungu
^loclfe^£!l SvX^(|>j,
yui^S&'&U-* 6 -
1 Mu aya iyi, Mulungu akuchenjeza amene akusonkhanitsa chumacho
nkumangochiunjika m'nkhokwe popanda kutulutsamo chopereka (zakaat).
Akawalanga nacho pa tsiku la chimaliziro ndi chilango chamoto. Tero,
tulutsamoni zakat m'chuma chanu. Musanyozere lamulo la Mulungu.
Surat 9. At-Taubah Juzu 10
399
1 • *>»
^ 4jjSj\ djj~*>
cholunjika. Choncho,
Musadzichitire nokha zoipa
m'menemo, Ndipo menyanani ndi
Amshrikina nonse Pamodzi monga
momwe akumenyana Nanu onse
pamodzi. Ndipo dziwani Kuti
Mulungu ali pamodzi ndi oopa. l
37. Ndithu, kutalikitsa ndi
kuchedwetsa (Mwezi wopatulika
kuti usafike Mwamsanga),
kumaonjezera kusakhulupirira
(Mwa Mulungu) Zoterozo
akusokera nazo amene
sadakhulupirire. Chaka china
amauyesa wosapatulika Pomwe
chaka china amauyesa Wopatulika
ndi cholinga chokwaniritsa
Chiwerengero cholingana ndi
miyezi Yomwe Mulungu
adaipatula kukhala yopatulika.
Choncho, chimene Mulungu
adaletsa, Amachiyesa chololedwa.
Zakometsedwa kwa Iwo zochita
zawo zoipa. Ndipo Mulungu
Sawatsogolera anthu
osakhulupirira. 2
1 Chiwerengero chamiyezi m'chaka, ndi khumi ndi iwiri monga mwalamulo la
Mulungu. M'miyeziyi muli miyezi inayi yopatulika yomwe ndi Rajabu, Zuli
kada, Zuli Haji ndi Muharamu. M'miyeziyi nkosaloledwa kuchita nkhondo
pokhapokha mutaputidwa ndi adani.
Kuichedwetsa miyezi yopatulika, kapena ina mwaiyo ndi kuichotsa
mumndondomeko wake umene Mulungu adaiika monga momwe ankachitira
anthu am'nyengo yaumbuli, kumawaonjezera kusakhulupirira anthu
osakhulupirira mwa Mulungu. Arabu m'nyengo yaumbuli amauyesa mwezi
wopatulika kukhala wosapatulika akafuna kuti achite nkhondo m'mweziwo.
Ndipo mwezi wosapatulika amauyesa wopatulika ncholinga choti akwaniritse
chiwerengero cha miyezi yopatulika yomwe Mulungu adaipatula. Zonsezi
zimachitika pofuna kukwaniritsa zilakolako zawo zoipa.
Siirat 9. At-Taubah Juzu 10
400
\ * *>»
^ <OjsJl Qjj* 1 *
38. E inu amene
mwakhulupirira! Mwatani;
mukauzidwa (kuti): "Pitani
mukachite Jihadi pa Njira ya
Mulungu, Mukudziremetsa
panthaka (Polemedwa ndi
kutulukako)? Kodi
Mwasangalatsidwa ndi moyo
wapadziko lapansi Kuposa moyo
watsiku lomaliza? Koma
Zosangalatsa za m'moyo wadziko
Lapansi (poyerekeza ndi moyo wa)
Tsiku lomaliza, ndi zochepa
Kwambiri.
39. Ngati simupita, akulangani
ndi Chilango chowawa, ndipo
abweretsa Anthu ena m'malo mwa
inu; ndipo Simungamuvutitse ndi
chilichonse (Ngati musiya kupita
kukamenyanira Panjira yake).
Ndipo Mulungu Ngokhoza
chilichonse.
40. Ngati simumthandiza
(Mtumuki Muhammad
{SAW}palibe kanthu), ndithu
Mulungu adamthandiza pamene
adamtulutsa Aja amene
sadakhulupirire. Pamene Adali
awiriwiri kuphanga Pamene
ankanenakwa mnzake:
"Usadandaule. Ndithu, Mulungu
ali Nafe pamodzi." Ndipo
Mulungu adatsitsa mpumulo Wake
pa iye, ndipo Adaamthangata ndi
asilikali ankhondo Omwe
®G*
. jA afcujl %fla> \j3i ijj^^yi
Surat 9. At-Taubah Juzu 10
401
1 * *>»
% ijjsJl 5jj-"
simudawaone. Ndipo mawu a
Amene sadakhulupirire adawachita
Kukhala apansi ndipo mawu a
Mulungu ndiwo apamwamba.
Ndipo Mulungu Ngopambana,
Ngwanzeru zakuya.
41. Pitani (mukamenyane) muli
opepuka Ndi olemedwa (anyamata
ndi Nkhalamba); menyerani njira
Ya Mulungu nchuma chanu ndi
Inu nomwe. Zimenezi nzabwino
Kwa inu ngati muli anthu odziwa.
42. Ukadakhala ulendo
wokafuna Zam'dziko zopepuka,
kuzipeza, ndi Ulendo wofupika,
ndithu akadakutsata
(Amunafikuna). Koma ulendo
Wamavutowu wakhala wautali
kwa iwo. Ndipo iwo alumbirira
Mulungu (Ponena kuti):
"Kukadakhala Kotheka kwa ife,
tikadapita nanu". (Pamawu awa),
akudziononga okha. Ndipo
Mulungu akudziwa kuti iwo
Ngabodza.
43. Mulungu wakukhululukira.
Bwanji Wawaloleza kutsalira?
(Ukadayembekeza) Kufikira
adziwike kwa iwe Amene akunena
zoona, ndikuti Uwadziwe abodza.
44. Sangakupemphe chilolezo
(Chotsala kunkhondo) amene
Akhulupirira mwa Mulungu ndi
tsiku Lomaliza kuti asapite
Surat 9. At-Taubah Juzu 10
402
\ * *>i
^ h$A\ 3jj-*»
kukamenyera (chipembedzo Cha
Mulungu) ndi chuma chawo ndi
Matupi a wo. Ndipo Mulungu
Akuwadziwa amene akumuopa.
45. Amakupempha chilolezo aja
amene Sakhulupirira Mulungu ndi
tsiku La Chimaliziro, ndipo mitima
Yawo yakaikira, ndipo iwo,
Chifukwa cha kukaika kwawo,
Akungotekeseka.
46. Akadafunadi kuti atuluke
(Kupita ku nkhondo)
akadakonzekera Zokonzekera za
kunkhondo; koma Mulungu
sadafune kuti iwo apiteko;
Choncho adawatsekereza, ndipo
Kudanenedwa: "Khalani pamodzi
ndi Otsalira".
47. Ngati akadatuluka nanu
pamodzi, Sakadakuonjezerani
chilichonse Koma chisokonezo
ndikuyenda Mwaukazitape pakati
panu Ndicholinga chokufunirani
chisokonezo, Ndipo mwa inu alipo
akuwamverera Ndipo Mulungu
Ngodziwa za oipa.
48.Ndithudi, akhala
akukufunirani chisokonezo
Kuyambira kale,
akusanthulirasanthulira Zinthu
(n'cholinga choti athane nawe)
Kufikira choonadi chadza
ndikuonekera Poyera lamulo la
Mulungu (lowakhaulitsa Ayuda)
iwo asakufuna.
ei^fc»fc&**4Wi
1 '
*&jj^&\$&<&
Surat 9. At-Taubah Juzu 10
403
> • *>i
^ 4j asjI 6j J""*
o oil u3 lyy£| 2u£*9* <^U*f?
49. Ndipo mwa iwo pali yemwe
akuti: "Ndiloreni ine (kuti nditsale
kunkhondo) Ndipo musandiponye
m'mayeso (kuopa Kuti
ndingalakwe ndikaona akazi
Akumeneko)" Ndithudi, iwo agwa
kale M'mayesero. Ndipo, ndithu,
Jahannama Ikawazinga mbali
zonse osakhulupirira.
50. Chikakupeza chabwino,
(iwe Mtumiki Muhammad (SAW)
ndi okutsatira) zimawanyansa
Ndipo vuto likakupeza amanena,
"Tidalingalira zinthu zathu kale.
(Nchifukwa chake mavuto
atizemba). Ndipo amatembenuka
nkupita uku Akukondwa. l
Sl.Nena: "Palibe chomwe
chitipeze koma Chimene Mulungu
watilembera. lye Ndi Mbuye
wathu". Choncho, Asilamu
Ayadzamire kwa Mulungu yekha.
52. Nena: "Kodi chilipo
chimene Mukuyembekezera mwa
ife posakhala Chimodzi mwa
zinthu ziwiri zabwino,
(Kupambana pankhondo
ndikupeza Zotolatola zake, kapena
kufa Ndikukalowa ku Munda wa
Mtendere)? Ndipo nafe
tikukuyembekezerani kuti
Mulungu akupatsani chilango
1 Achinyengo sadali kufunira zabwino Asilamu ngakhale kuti adali
kudzipachika m'gulu la Asilamu mwachinyengo. Ankati vuto likawagwera
Asilamu amasangalala. Koma chikawadzera chabwino amadandaula.
' 9 9 <>'6 9 k ' *\f-
Surat 9. At-Taubah Juzu 10
404
\ • *>»
^ 4jjiJl djj-*»
Chochokera kwa lye, kapena
kupyolera M'manja mwathu.
Choncho Bayembekezerani;
nafenso Tikuyembekezera nanu
limodzi".
53. Nena (kwa Amunafikina):
"Perekani (Chuma chanu)
mwachifuniro kapena Mosafuna
sichizalandiridwa kwa inu.
Ndithu, inu ndinu anthu Otuluka
m'chilamulo cha Mulungu".
54. Palibe chomwe chidaletsa
kulandiridwa Kwa zopereka zawo
koma chifukwa Chakuti iwo
sadakhulupirire Mulungu Ndi
Mtumiki Wake; ndiponso sapita
Kopemphera koma mwaulesi;
ndipo Sapereka chopereka Koma
monyinyirika.
55. Ndipo chisakudolole chuma
chawo Kapena ana awo. Ndithu,
Mulungu Akufuna kuwalanga nazo
pamoyo Wapadziko lapansi, ndi
kuti mitima Yawo ichoke ali
osakhulupirira.
56. Akulumbira (m'dzina la)
Mulungu Kuti iwo ali pamodzi ndi
inu; Pomwe iwo sali pamodzi nanu
koma iwo Ndi anthu amantha.
57. Ngati akadapeza linga
lothawiramo Pena mapanga
kapena pamalo pena Polowa
(ndithu) akadathawira kumeneko
Mwa liwiro.
9 9t,l<<9 99 *\'Z.& >< 9*"S\"
Surat 9. At-Taubah Juzu 10
405
\ • *>i
\ hj£\ djj-*>
58. Ndipo alipo ena mwa iwo
(Amunafikina) amene akukunena
(Mkugawa kwako) sadaka:
akapatsidwa Kanthu m'menemo
amakondwera koma Akapanda
kupatsidwa akukwiya nawe.
59. Ngati iwo akadakondwera
ndi chimene Mulungu ndi Mtumiki
Wake wawapatsa, Nanena:
"Mulungu watikwanira.
Posachedwapa Mulungu ndi
Mtumiki Wake atipatsa zabwino
Zake. Ndithu, ife tikufunitsitsa
kwa Mulungu." (Ndiye kuti
Mulungu Akadawapatsa zambiri).
60. Ndithu,zakati ndi ya
mafukara, Masikini, ogwira ntchito
yosonkhetsa Zakatiyo, owalimbitsa
mitima yawo (Pa chisilamu amene
alowa kumene), Kuombolera
akapolo kuti akhale mfulu,
Kuthandizira amene ali
m'ngongole; Kuipereka pa njira ya
Mulungu; Ndi kuwapatsa
apaulendo (omwe alibe
Choyendera). Hi ndi lamulo
lochokera kwa Mulungu, ndipo
Mulungu Ngodziwa Kwabasi,
Ngwanzeru zakuya.
©<a
" 9 S?Z 9 ' 9>\<&9
%
©:
M'ndime iyi Mulungu akutifotokozera magulu a anthu amene ngoyenera
kuwagawira chuma cha zakati. Iwo ndi awa:-
1 . Osauka amene alibe zokwanira pa zofunikira pa moyo wawo.
2. Osauka amene sangagwire ntchito nkudzipezera okha chakudya (Masikini).
3. Amene akusonkhetsa chuma cha zakaticho omwe ntchito yawo
ndiyokhayo.
Surat 9. At-Taubah Juzu 10
406
1* *>»
^ ijjjl Ojj-j
61. Ndipo alipo ena mwaiwo
amene Akuzunza Mneneri ponena
kuti: "Uyu ndi khutu (lomvetsera
nkhani Iliyonse popanda
kuiganizira)" Nena: "Ndi khutu
labwino kwa inu". (Mwini
khutulo) amakhulupirira Mulungu:
Amakhulupirira (Zonena) za
Asilamu, ndipo (iye) Ndi mtendere
kwa amene akhulupirira Mwa inu.
Ndipo amene akuvutitsa Mtumiki
wa Mulungu adzakhala ndi
Chilango chopweteka.
62. Akulumbira kwa inu
potchula Dzina la Mulungu kuti
akukondweretseni (Chikhalirecho
akunyoza Mulungu ndi Mtumiki
Wake), pomwe Mulungu ndi
Mtumiki Wake ndiye Wofunika
kuti amkondweretse ngati Iwo
ngokhulupiriradi (mwachoonadi).
63. Kodi sadziwa kuti amene
akulimbana Ndi Mulungu ndi
Mtumiki Wake, adzapeza Moto wa
Jahannama Ndi kukhalamo
muyaya? Kumeneko Ndi kuyaluka
kwakukulu.
64. Amunafikina akuopa
kuwatsikira Sura yomwe
4. Amene angolowa kumene m'Chisilamu omwe akuyembekezedwa kuti
akapatsidwa adzalimbikitsidwa mitima yawo pachipembedzochi.
5. Amene afuna kudziombola ku ukapolo.
6. Amene akulephera kulipira ngongole ya choonadi.
7. Amene akuchita Jihadi panjira ya Mulungu.
8. Wapaulendo amene alibe choyendera (ndalama zoyendera).
Surat 9. At-Taubah Juzu 10
407
S * *>»
^ 4jj^it *j>**'
ingawafotokozere (Zachinyengo
chawo) chomwe chili M'mitima
mwawo. Nena: "Chitani
Zachipongwe. Ndithu, Mulungu
atulutsira Poyera zomwe
mukuziopazo (kuti Asilamu
Asazidziwe).
65. Ndipo utawafunsa
(chifukwa ninji Chipembedzo
akuchichitira Chipongwe)?Anena:
"Ife timangosereula Ndi kusewera
basi (palibe china)." Nena:
"Mumachitira Mulungu ndi aya
Zake ndi Mtumiki Wake
zachipongwe?"
66. Musapereke madandaulo
(abodza) Ndithu mwaonetsera
ukafiri wanu Poyera, pambuyo
pakukhulupirira Kwanu
(kwabodza). Ngati gulu lina mwa
inu Tilikhululukira (litalapa), gulu
lina tililanga Chifukwa cha
kupitiriza kulakwa kwawo.
67. Amunafikina aamuna ndi
Amunafikina Aakazi onse
khalidwe lawo ndi Limodzi.
Amalamulira zoipa ndikuletsa
Zabwino, ndipo amafumbata
manja awo (Sathandiza
pazabwino). Amuiwala Mulungu
(Ponyozera malamulo Ake).
Iyenso wawaiwala (Powanyozera).
Ndithu, Amunafikina ngotuluka
M'chilamulo cha Mulungu.
-^^V-
Tip"
£y£»*s£*> <LjL&i$J <&*£$
'" 9 *" X 9 A\ ' >9> 9 x's **'
Surat 9. At-Taubah Juzu 10
408
\ • *>i
^ 4jjsJI 5jJ-*»
68. Mulungu walonjeza
Amunafikina aamuna Ndi
Amunafikina aakazi ndi Akafiri,
Moto wa Jahannama, akakhala
m'menemo Muyaya. Umenewo
ukukwanira Kwa iwo (kuwalanga).
Ndipo Mulungu Wawatemberera,
ndipo iwo adzapeza Chilango cha
nthawi zonse.
69. (Inu osakhulupirira) ndinu
ofanana Ndi amene adalipo
patsogolo panu. (Tikuonongani
monga tidawaonongera Iwo;
koma) iwo adali ndi nyonga
Zambiri kuposa inu; adalinso ndi
chuma Chambiri ndi ana ambiri
kuposa inu. Choncho,
adasangalalira gawo lawo Inunso
mukusangalalira gawo lanu Monga
momwe adasangalalira gawo lawo
omwe Adalipo patsogolo panu,
ndipo mwamira M'zoipa monga
momwe adamirira iwo. A wo ndi
amene zochita zawo zidapita
Pachabe padziko lapansi ndi
patsiku Lomaliza. Awo ndi omwe
ali otaika.
70. Kodi siidawadzere nkhani
ya amene Adalipo patsogolo pawo,
anthu a Nuhi, Adi ndi Samudu;
anthu a Ibrahim Ndi anthu a ku
Madiyana ndi (anthu) a M'Midzi
imene idatembenuzidwa
Kumwamba kukhala pansi, pansi
kukhala Kumwamba? Atumiki
Surat 9. At-Taubah Juzu 10
409 1 • *>■»
H AJJ^I <*JJ~"
awo adawadzera ndi Zisonyezo
zoonekera (koma adakana
Kuwatsata.Choncho, Mulungu
adawaononga). Mulungu
sadawachitire choipa, koma
Ankadzichitira okha zoipa.
71. Okhulupirira aamua ndi
okhulupirira Aakazi, ndiabwenzi
omvana pakati Pawo. Amalamula
zabwino ndikuletsa zoipa ndipo
Amapemphera swalandi
Kupereka chopereka (zakaat), ndi
Kumvera Mulungu ndi Mtumiki
wake. Awo ndi omwe Mulungu
adzawachitira Chifundo. Ndithu,
Mulungu Ngwamphamvu Zoposa,
Ngwanzeru zakuya.
72. Mulungu waalonjeza
okhulupirira aamuna Ndi
okhulupirira aakazi Minda yomwe
pansi Ndi patsogolo pake mitsinje
Ikuyenda adzakhala m'menemo
nthawi zonse. Ndi mokhala
mwabwino m' Minda ya nthawi
Zonse (yosatha) .Ndipo chiyanjo
Chochokera kwa Mulungu ndi
chachikulu (Omwe ndi mtendere
waukulu kwambiri Kuposa zonse).
Kumeneko ndiko kupambana zedi.
73. E iwe Mneneri! Limbana
ndi Osakhulupirira ndi
Amunafikina ndipo uwaumire
mtima. Mbuto yawo ndi ku
Jahannama. Taonani kuipa kwa
Malo obwelera.
' 999 *?* 'K»'*ll < '9*9'*
99 **. S9y *
Surat 9. At-Taubah Juzu 10
410 \> ' *>'
S 3->jiJt &JJ**
74. (Amunafikina pambuyo
pomunenera Mulungu ndi Mtumiki
Wake mawu Oipa), akulumbira
potchula dzina La Mulungu (kuti)
sadanene (Zonyoza), pomwe
adanenadi mawu Aukafiri, ndipo
akana chikhulupiriro pambuyo
posonyeza Chisilamu Chawo
(chabodza); ndipo adatsimikiza
(kuchita) zomwe sadathe Kuzifika.
Komatu sadaone choipa (M'kudza
kwa Chisilamu), koma kuti
Mulungu ndi Mtumiki Wake
adawalemeretsa Ndi zabwino zake.
Choncho Ngati alapa, zikhala
zabwino kwa iwo. Ndipo ngati
anyoza, Mulungu Awalanga ndi
chilango chowawa Pamoyo
wapadziko lapansi ndi Patsiku
lomaliza. Ndipo sadzakhala Ndi
mtetezi ngakhale aliyense
Wowapulumutsa padziko.
75. Pakati pawo alipo amene
adalonjeza Mulungu kuti, "Ngati
atipatsa Zabwino zake (chuma)
tidzapereka sadaka ndi kukhala
m'gulu la Ochita zabwino."
76. Koma pamene adawapatsa
Zabwino zakezo, adazichitira
Umbombo nanyoza,
Natembenukira kutali Ndi
Mulungu.
77. Choncho, chotsatira chake
adawaika Chinyengo m'mitima
mwawo kufikira Tsiku lokumana
Siirat 9. At-Taubah Juzu 10
411
> • *j*-l
^ 4jjs)| 9jj**t
naye (Mulungu), Chifukwa cha
kuphwanya kwawo zomwe
Adamulonjeza Mulungu. Ndiponso
Chifukwa cha zabodza zomwe
ankanena.
78. Kodi sadziwa kuti Mulungu
Akudziwa zobisika zawo ndi
Manong'onong'o awo Ndikuti
Mulungu Ngodziwa zinthu
zamseri?
79. Amene akuwanena Asilamu
opereka Sadaka yambiri, ndiponso
(amene Akunyoza) amene sapeza
(Chopereka), koma chinthu
Chochepa; ndikumawachitira
Chipongwe, Mulungu adzawalipira
Chipongwe chawocho. I wo
adzapeza Chilango chopweteka.
80. (EiweMtumiki!)
Uwapemphere Chikhululuko
(Amunafikina) Kapena
usawapemphere, (zonsezo
Nchimodzimodzi). Ngakhale
Utawapemphera chikhululuko
Chochuluka kwabasi mokwanira
Makumi asanu ndi awiri (70)
Mulungu sangawakhululukire.
Zimenezo nchifukwa chakuti iwo
Akana Mulungu ndi Mtumiki
Wake. Ndipo Mulungu satsogolera
anthu Ophwanya malamulo Ake.
81. Akondwa amene adasiidwa
m'mbuyo (Osapita kunkhondo)
chifukwa Chakukhala kwawo
©&>$#£
Surat 9. At-Taubah Juzu 10
412
\ * *>i
^ 4jjiil 0jj-*»
m'mbuyo Polekana ndi Mtumiki
wa Mulungu, nakuda kumenyana
pa Njira ya Mulungu ndi chuma
chawo Ndi moyo wawo, nati (kwa
anzawo): "Musapite (kunkhondo)
m'nthawi Yotenthayi." Auze:
"Moto wa Jahannama ngotentha
kwambiri Akadakhala
akuzindikira."
82, Choncho, aseke pang'ono
(padziko Lapansi).Ndipo adzalira
kwambiri (Patsiku lomaliza); (iyo
ndi) Mphoto ya zomwe adapeza
(Kuchokera m'zochita zawo
zoipa). 1
83, Ngati Mulungu akubweza
(kunkhondoko) Nkufika kugulu
lina la mwa iwo ndipo Iwo
nkukupempha chilolezo
chakutuluka (Kupita kunkhondo,
zomwe Zidzapezeke mtsogolo),
nena: "Inu Simudzatuluka nane
mpaka muyaya, Ngakhalenso
kumenyana ndi adani Pamodzi
nane; inu mudakonda Kukhala
nthawi yoyamba; choncho Khalani
(nthawi zonse) pamodzi Ndi
otsalira (pambuyo)."
84, Ndipo usamupempherere
konse Aliyense wa iwo yemwe
-'*- 9 <"/\<>$i*\Z\*'' *'*
*&%&*$>
~»1* <
%&
%\®<&2&£&><&>3S
Anthu achinyengo (Amunafikina) adakana kupita naye limodzi Mtumiki
(SAW) kunkhondo namasangalalira kukhala kwawoko. Ndipo apa Mulungu
akuwauza kuti asangalale ndi kuseka pang'ono. Koma adzalira ndi kukukuta
monn ntl-f^nii wsi+'sIS
Surat 9. At-Taubah Juzu 10
413
s « t>l
^ *ujJl 5jj~»>
wamwalira, Ndipo usaimirire
pamanda ake (Kumpempherera);
ndithu, iwo Amukana Mulungu ndi
Mtumiki Wake, Ndipo amwalira
uku ali opandukira Chilamulo cha
Mulungu.
85. Ndipo chisakudolole chuma
cha wo Kapena ana awo. Ndithu
Mulungu akufuna kuwalanga Ndi
zimenezo padziko Lapansi, ndi
kuti mizimu Yawo ichoke ali
Osakhulupirira.
86. Ndipo Sura
ikavumbulutsidwa (yonena
Kuti):"Mkhulupirireni Mulungu
ndi kumenya Nkhondo (chifukwa
cha chipembedzo Chake) Pamodzi
ndi Mtumiki wake, " Opeza bwino
mwa Iwo akukupempha chilolezo
(Kuti asapite kunkhondo), ndipo
akuti: "Tisiye tikhale pamodzi ndi
okhala (Otsalira m'mbuyo)."
87. Akondwera pokhala limodzi
ndi Otsalira m'mbuyo (akazi ndi
ana). Ndipo mitima yawo
yadindidwa chidindo
(Yatsekedwa), choncho iwo
sazindikira.
88. Koma Mtumiki ndi amene
Akhulupirira pamodzi ndi iye
Amenya nkhondo Ndi chuma
cha wo ndi matupi awo. Iwo wo
ndi wo opeza zabwino, Ndiponso
iwowo Ndiwo opambana.
Surat 9. At-Taubah Juzu 10
414
) * *>i
^ iij^l Sjj-j
89. Mulungu wawakonzera
minda yoyenda Mitsinje pansi ndi
patsogolo pake; adzakhala
M'menemo muyaya. Kumeneko
ndiko Kupambana kwakukulu.
90. Ndipo adza eni madandaulo
(oona), mwa anthu Am'chipululu
(omwe ndi Asilamu) kuti
Awapatse chilolezo (chosapita
kunkhondo). Koma adakhala
(popanda kupempha chilolezo
Kwa Mtumiki ) amene amunamiza
Mulungu ndi Mtumiki wake.
(Amenewa ndi Amunafikina omwe
Amadzitcha kuti ndi Asilamu
pomwe sadali Asilamu). Mwa iwo
amene sadakhulupirire Mulungu
chiwapeza chilango chopweteka.
91. Palibe tchimo (kusapita
kunkhondo) Kwa amene ali ofooka
(pachilengedwe Chawo) ngakhale
kwa odwala, ngakhale kwa Omwe
sapeza chothandiza (paulendo
ngakhale Chosiira akubanja lawo)
ngati iwo ali ndi Cholinga
chabwino pa Mulungu ndi
Mtumiki Wake. Palibe njira
(yowadzudzulira) amene Akuchita
zabwino. Ndipo Mulungu
Ngokhululuka kwabasi,
Ngwachisoni.
92. Ndiponso (palibe tchimo)
kwa Amene akukudzera kuti
uwatenge (Kupita kunkhondo) iwe
uunena: "Ndilibe choti
Surat 9. At-Taubah Juzu 11
415
> > *>»
^ 4jy)\ dj^-*>
ndikunyamulireni," Nabwera maso
awo Akutuluka misozi chifukwa
Chakudandaula posapeza zimene
Zingawathandize paulendowo.
93. Ndithu, njira
(yodzudzulidwa) ili pa amene
Akukupempha chilolezo (choti
asapite kunkhondo Ndikusiyanso
kupereka chuma chawo) Pomwe
iwo ngolemera. Akonda kukhala
pamodzi Ndi otsala m'mbuyo.
Ndipo Mulungu wadinda Chidindo
(chamantha) m'mitima mwawo,
tero Sadziwa (chilichonse
cho wathandidza) .
94. Akudandaulirani
madandaulo Mukabwerera kwa
iwo (ndi kukumana Nawo). Nena:
"Musapereke madandaulo;
Sitikukhulupirirani. Mulungu
watifotokozera kale Nkhani zanu.
Posachedwa Mulungu ndi Mtumiki
Wake aona zochita zanu, Kenako
muzabwezedwa (Pambuyo pa
imfa) kwa Wodziwa Zamseri ndi
zoonekera. Choncho, lye
adzakufotokozerani zimene Mudali
kuchita."
95. Mukabwerera kwa iwo,
adzalumbira M'dzina la Mulungu
kwa inu kuti Muwasiye
(musawachite kanthu). Choncho,
apatukireni. Ndithu, iwo Ndi uve
ndipo malo awo ndi ku Jahannama.
Iyi ndi mphoto ya Zomwe adali
Surat 9. At-Taubah Juzu 11
416
U ftjA-i
h ^jsi* *jj-*'
kupeza (kuchokera m'zochita
Zawo zoipa).
96. Akulumbira kwa inu kuti
muwayanje Ngati inu muwayanja,
(dziwani kuti Mulungu
sakuwayanja). Ndithu, Mulungu
sayanja anthu otuluka
M'chilamulo.
97. Anthu am'chipululu
ngoyipitsitsa Pakusakhulupirira ndi
uchiphamaso ndiponso Ngoyenera
kusazindikira malire a Zomwe
Mulungu wavumbulutsa kwa
mtumiki Wake. Komatu Mulungu
Ngodziwa Kwambiri, Ngwanzeru
zakuya.
98. Ndipo alipo ena mwa anthu
a m'chipululu Omwe amachichita
chimene Akupereka pa njira ya
Mulungu Ngati dipo (laulere
lopanda phindu,) Ndikumadikira
kwa inu kuti miriri Ikupezeni.
Miriri yoipa ili paiwo; (Iwapeza
okha). Ndipo Mulungu
Ngwakumva (nkhani iliyonse),
Wodziwa (Chilichonse).
99. Ndipo alipo ena mwa anthu
A m'chipululu omwe
akukhulupirira Mulungu ndi tsiku
lomaliza ndipo Zomwe akupereka
(pa njira ya Mulungu) amazichita
monga Chodziyandikitsira nacho
kwa Mulungu, ndi (chowachititsa
kuti Apeze) mapemphero a
Surat 9. At-Taubah Juzu 11
417
n *>»
^ i»jJ* Ojj~rf
mtumiki. Tamverani! Ndithu,
zimenezo Ndizinthu
zowayandikitsa kwa Mulungu.
Mulungu adzawalowetsa
Kumtendere Wake. Ndithu,
Mulungu Ngokhululuka kwambiri,
Ngwachisoni.
lOO.Ndipo amene adatsogolera
poyamba, Am'gulu la Amuhajirina
ndi Answari, ndi omwe
adawatsatira Iwo mwaubwino,
Mulungu adzakondwa Nawo.
Naonso adzakondwera Naye (pa
Zomwe adzapatsidwa ndi
Mulungu.) Ndipo wawakonzera
minda yomwe mitsinje Ikuyenda
pansipake; adzakhala M'menemo
muyaya. Uko ndikupambana
Kwakukulu.
101* Ndipo ena mwa anthu
am'chipululu omwe Akukhala
m'mphepete mwanu (M'mphepete
mwa mzinda wa Madina) Alipo
Amunafikina (achinyengo);
Ndiponso eni Mzinda wa Madina
Aphunzira ukatswiri wachinyengo
(Kotero kuti) sukuwadziwa. Ife
Tikuwadziwa. Tiwalanga kawiri
(Padziko lapansi). Ndipo kenako
Adzabwezedwa kuchilango
chachikulu (Patsiku lomaliza).
102. Ndipo alipo ena omwe
avomereza Uchimo wawo (nalapa
kwa Mulungu). Asakaniza zochita
zabwino ndi Zina zoipa. Ndithu,
Surat 9. At-Taubah Juzu 11
418
U fr>»
^ hyA\ <*jj~»»
Mulungu Alandira kulapa kwawo.
Ndithu Mulungu Ngokhululuka,
Ngwachisoni.
103. Tenga sadaka m'chuma
chawo Kuti uwayeretse nayo
(kumachimo Ndi umbombo)
ndikuti uwatukulire nayo
Ulemerero wawo kwa Mulungu;
ndipo Apemphere ( zabwino ndi
chiongoko). Ndithu, mapemphero
ako kwa iwo Ndi mpumulo.
Ndipo Mulungu Ngwakumva,
Wodziwa (chilichonse.)
104. Kodi sadziwa kuti
Mulungu Amalandira kulapa kwa
akapolo Ake, ndi kulandira sadaka,
Ndikuti Mulungu ndi Mwini
kulandira Kulapa mochuluka
ndiponso Wachisoni.
105. Ndipo auze: "Chitani
(zinthu Zabwino); Mulungu ndi
Mtumiki Wake ndi Asilamu aona
zochita Zanuzo posachedwa.
Ndipo (kenako) Mudzabwezedwa
kwa Wodziwa zamseri Ndi
zoonekera poyera. lye adzakuuzani
Zonse (zimene) mudali kuchita."
106. Ndipo aliponso ena amene
(adagwa M'machimo omwe)
akudikirira Lamulo la Mulungu,
(kulapa kwawo
Sikunavomerezekebe), kapena
Awalanga kapenanso awavomera
Kulapa kwawo .Ndipo Mulungu
9 > 9*\'&4'JZ " 9 \\' 9 i 9 9 K
* 9\'9&
Surat 9. At-Taubah Juzu 11
419 > > >>>
H *JjA\ ^JJ - "**
Ngodziwa (Khalidwe lawo ndi
zomwe zili M'mitima mwawo),
Wanzeru zakuya (Pazonse zomwe
akuchita kwa anthu Ake popereka
mphoto ndi chilango).
107. Ndipo (alipo Amunafikina
ena) amene Adamanga msikiti ndi
cholinga chodzetsa Masautso ndi
(kulimbikitsa) kusakhulupirira
Mulungu ndi kuwagawa Asilamu
(mu umodzi Wawo) ndi kuupanga
kukhala msasa wa omwe
Adamthira nkhondo Mulungu ndi
Mtumiki Wake Kale. Ndithu,
alumbira (ndikunena): "Sitidali
ncholinga china (pomanga
Msikitiwo) koma ubwino." Koma
Mulungu akuikira umboni kuti iwo
Ngabodza.
108. Usaimirire (ndi
kupemphera) m'menemo
Mpang'ono pomwe. Ndithu,msikiti
Umene udakhazikitsidwa poyamba
Ncholinga choopa Mulungu ndiwo
Wofunika kuti uimirire m'menemo
(Ndi kupemphera). M'menemo
muli Anthu okonda kudziyeretsa
(matupi Ndi mitima yawo); ndipo
Mulungu Amakonda odziyeretsa.
109.Kodi amene wakhazikitsa
maziko Achomanga chake
chifukwa choopa Mulungu ndi
kufunafuna chiyanjo (Chake),
sindiye wabwino, kapena Yemwe
wakhazikitsa maziko Achomanga
Siirat 9. At-Taubah Juzu 11
420
) \ tji-i
^ hjd\ djj~*
chake m'mphepete mwa Dzenje
(lakuya) lomwe dothi lake
Likugumukira (m'dzenjemo) ndipo
Nkugwa pamodzi naye mmoto wa
Jahannama, ( ameneyu ndiye
wabwino?) Ndithudi, Mulungu
saongolera anthu Ochita zoipa.
110. Chomanga chawo chomwe
adachimanga Sichileka kudzetsa
chikaiko ndi Kusakhazikika
m'mitima mwawo Kufikira mitima
yawo itaduka (Ndi madandaulo
kapena imfa). Ndipo Mulungu
Ngodziwa (chilichonse),
Ngwanzeru zakuya
(M'zochitachita Zake).
lll.Ndithu, Mulungu wagula
kwa Asilamu Moyo wawo ndi
chumachawo (kuti Apereke moyo
wawo ndi chuma chawo Pomenya
nkhondo pa njira ya Mulungu) kuti
iwo alandire Munda Wamtendere.
Akumenya nkhondo pa Njira ya
Mulungu, ndipo akupha Ndi
kuphedwa. Hi ndi lonjezo Loona
lokakamizika pa lye lomwe
Likupezeka m'Buku la Taurati,
Injili ndi Qur'an. Kodi ndani
Wokwaniritsa lonjezo lake kuposa
Mulungu? Choncho kondwerani
ndi Kugulitsa kwanu komwe
mwagulitsana Naye. Kumeneko
ndiko kupambana kwakukulu.
112. (A wo amene alonjezedwa
kupeza izi, Ndi) omwe amalapa
£>>xJ>JI 6i^l <z)j?0
Surat 9. At-Taubah Juzu 11
421
U ftjA-i
^ 4jjJ| 5jJ-*>
(akalakwa); Ochita mapemphero
(awo m'njira Yoyenera); otamanda
Mulungu Kwambiri; ochulukitsa
kusala (Swaumu kapena
oyendayenda padziko Ncholinga
chochitira zabwino anthu)
Owerama, ogwetsa nkhope zawo
pansi; Olamula zabwino; oletsa
zoipa ndi Osunga malire a
Mulungu (malamulo Ake).
Choncho, auze nkhani yabwino
Awo amene akhulupirira.
113. Nkosayenera kwa Mneneri
ndi amene Akhulupirira
kuwapemphera chikhululuko
Amushirikina (opembedza
Mafano) ngakhale atakhala abale
Awo, pambuyo poonekera Kwa
iwo kuti iwowo Ndi anthu
akumoto.
114.Ndipo Ibrahim
sadampemphere bambo Wake
chikhululuko koma chifukwa Cha
lonjezo lomwe adamulonjeza.
Koma pamene zidaonekera kwa
iye Poyera kuti iye (bambo wake)
ndi Mdani wa Mulungu,
Adadzipatula kwa iye. Ndithudi,
Ibrahim adali wochulukitsa
kupempha Mulungu
modzichepetsa, woleza mtima.
HS.Ndipo Mulungu
sangasokeretse Anthu (ndi
kupititsa chilango pa iwo)
pambuyo Powaongolera ku
Surat 9. At-Taubah Juzu 11
422
U *>i
^ AjjsJl &jj**
chisilamu; koma Pokhapokha
atawonetsa poyera kwa iwo
Zimene zingafunike kuzipewa
(Powavumbulutsira chivumbulutso
Kudzera kwa mtumiki. Koma
akapanda Kupewa zofunika
kuzipewa, ndi pomwe
Amawerengedwa kuti ndi anthu
oipa). Ndithu, Mulungu Ngodziwa
chilichonse.
1 16. Ndithudi,Mulungu ndi
Wake Ufumu wakumwamba Ndi
pansi. Amapereka moyo ndi Imfa.
Inu mulibe mtetezi ngakhale
Mthandizi koma Mulungu basi.
117,Ndithu,Mulungu wafunira
zabwino MtumikiWake ndi
Amuhajirina ndi Answari amene
adamtsatira iye
(Muhammad{SAW}) m'nthawi
yamasautso (Pokamenyana ndi
Aroma pankhondo ya Tabuk),
nthawi yomwe mitima ya ena A
iwo idatsala pang'ono kupotoka
(Kutsata machitidwe achikafiri);
Kenako Mulungu
adawatembenukira ndi Chifundo.
Ndithu, Iye (Mulungu). Kwa iwo
Ngodekha, Ngwachisoni. 1
«S8^<^&^
Nkhondo ya Tabuk idachitika m'mwezi wa Rajab m'chaka cha chisanu
nchinayi chakusamuka. Idali pakati pa Asilamu ndi Aroma. Gulu lankhondo la
Chisilamu lomwe lidapita kunkhondo linkatchedwa "Gulu la Masautso" chifukwa
kukonzekera kwa nkhondoyi kudachitika m'nyengo yamasautso kwa anthu.
Ndipo pamene Mtumiki adafika ku Tabuk, adadza Yohane namvana kuti
pasakhale nkhondo.
M'malo mwake iye adzapereka "Jiziya" (msonkho), motero Mtumiki adabwerera
ku Madina. lyi idali nkhondo yake yomaliza.
Siirat 9. At-Taubah Juzu 11
423
n tjA-i
^ ^j^f ^jj"**
118.Ndiponso
(adawatembenukira mwachifundo)
Aja atatu amene adawadikiritsa
(Pakusavomera msanga kulapa
kwawo Kufikira pamene dziko
Lidawapana ngakhale lidali
lophanuka Nabanika m'mitima
mwawo Natsimikiza kuti palibe
Komuthawira Mulungu (kwina)
Koma kwa lye (Mulungu polapa).
Kenako (Mulungu) adawatsogolera
Kulapa kuti alape. Ndithu,
Mulungu Ngolandira kulapa,
Ngwachisoni.
119.E inu amene
mwakhulupirira! Opani Mulungu:
ndipo khalani pamodzi ndi oona
(Amene akuchitsimikiza Chisilamu
chawo Ndi zochita zawo, osati
kungoyankhula Pakamwa pokha).
120.Nkosayenera kwa anthu
amumzinda Wa Madina ndi amene
ali M'mphepete mwawo, mwa
anthu Am'chipululu, kutsalira
M'mbuyo mwa Mtumiki wa
Mulungu (poleka Kutsagana naye
kunkhondo), Ndiponso
nkosayenera kwa iwo Kudzikonda
okha kuposa iye (Mtumiki) .
Zimenezo Nchifukwa choti iwo
silingaapeze Ludzu kapena mavuto
kapena Njala pa njira ya Mulungu,
ndipo Sangaponde malo okwiitsa
osakhulupirira, Ndipo sangampatse
mdani Chompatsa chilichonse
Surat 9. At-Taubah Juzu 11
424
U *>»
^ hjd\ Ojj-a
chopweteka Koma kulembedwa
kwa iwo pa Zimenezo (kuti
achita) ntchito Yabwino.
Ndithu,Mulungu sawononga
Malipiro a ochita zabwino.
121.Ndipo sangapereke
chopereka Chaching'ono kapena
chachikulu, ndipo Sangadutse
mtunda wachigwa; koma
Kulembedwa kwa iwo, Kuti
Mulungu adzawalipira Malipiro
abwino pazomwe adali kuchita.
122.Nkosafunika kwa Asilamu
kutuluka Onse (m'midzi yawo
kupita ku Madina ndi kusiya midzi
yopanda Anthu). Nchifukwa ninji
Silituluka gulu m'fuko lililonse
Mwa iwo (ndikupita ku Madina
kwa Mtumiki) kukaphunzira
bwino za Chipembedzo, ndipo
akawachenjeze Anthu awo
akazabwerera kwa iwo kuti aope.
123. E inuamene
mwakhulupirira! Menyani
nkhondo ndi awo osakhulupirira
Amene ali pafupi nanu, ndipo
apeze kuuma (Mtima) mwa inu.
Ndipo dziwani kuti ndithu
Mulungu ali pamodzi ndi oopa
(lye).
124. Ndipo nthawi zonse sura
(yatsopano) Ikavumbulutsidwa,
alipo mwa iwo (Amunafikina)
amene akunena: "Ndani mwa inu
Siirat 9. At-Taubah Juzu 11 I 425 I \ > *>
^ hyd\ Sjj-j
sura lyi yamuonjezera
Chikhulupiriro?" Koma amene
Akhulupirira yawaonjezera
Chikhulupiriro ndipo iwo
akukondwera.
125. Koma amene ali ndi
matenda m'mitima Mwawo,
yawaonjezera zoipa Pamwamba
pazoipa zomwe adali nazo, Ndipo
akufa ali osakhulupirira.
126. Kodi saona kuti iwo
akuyesedwa Mayeso chaka
chilichonse kamodzi, Kapena
kawiri, (kapena kochulukirapo)?
Koma salapa (kwa Mulungu)
ndiponso Iwo sakumbukira.
127. Ndipo nthawi iliyonse sura
yatsopano Ikavumbulutsidwa
amayang'anana (Iwo amunafikina
kuti Athawe, asamvere mawu ake,
uku Akuuzana pakati pawo):
"Kodi alipo Amene akukuonani?"
Kenako Amatembenuka
nkuthawa. Tero, Mulungu
waikhotetsa Mitima yawo
chifukwa chakuti iwo ndi Anthu
osazindikira.
128. Ndithu, wakudzerani
Mtumiki Wochokera mwa inu.
Zikumudandaulitsa lye zomwe
zikukuvutitsani; lye ngoikira
mtima pa inu Pokufunirani
zabwino; Ndipo pa okhulupirira
Ngodekha ndiponso ngwachisoni.
\*1
%%&jyj±
Surat 9. At-Taubah Juzu 11
426
\\ *jJH
^ 4jjsil Qjj->
129. Koma ngati (iwo) apitiriza
Kunyoza (awo osakhulupirira),
Nena: "Mulungu wandikwanira
(Palibe vuto lingapezeke
Kuchokera kwa inu) palibe Woti
nkupembedzedwa Koma lye basi.
Ndatsamira Kwa lye. Ndipo lye,
ndi Bwana wa Mpando waukulu!"
Surat 10. Yunus
Juzu 11
427
U *>»
^ ♦ a^y- 5 j>*
SURAT YUNUS X
Yayamba ndikufotokoza za ulemelero wa Buku la Qur'an ndi
zomwe Amshirikina ankamunenera Mtumiki Muhammad
(SAW). Kenako yafotokoza za dziko ndi zisonyezo za Mulungu
zomwe zili m'menemo zosonyeza kukhoza kwake.
Surayi yakambanso za mphoto ya tsiku lomaliza (tsiku la
Kiyama) ndi machitidwe a Mulungu kwa osakhulupirira. Ndipo
yafotokozanso za chikhalidwe cha anthu pamavuto ndi
pamtendere. Yakambanso kuti Mulungu ndiye ali ndi mphamvu
pachilichonse, osati mafano. Ndipo yawatokosa amene akuti
Qur'an njopeka kuti apeke sura imodzi yonga ngati ya
m'Qur'an.
Msurayi Mulungu akuchenjezanso anthu za chilango Chake
choopsa, ndi momwe mitima ya anthu ilili. Ndipo yanenetsa kuti
Mulungu akuona chilichonse chimene anthu akuchita.
Kenako yafotokoza mawu omutonthoza Mtumiki
pakuwawidwa kwake ndi kusakhulupirira kwa anthu ake pomwe
adali kuwauza momveka bwino. Ndipo yamthonthoza potchula
zomwe aneneri ankapezana nazo kwa anthu awo. Choncho
yadza nkhani ya Nuhi,nkhani ya Musa ndi Haarun pamodzi ndi
Farawo ndi ana a Israeli. Ndipo kenako yanena nkhani ya Yunus
yemwe Surayi idatchulidwa ndi dzina lake.
Surat 10. Yunus
Juzu 11
428
\ \ *>i
iT*?- d J>"
Surat Yunus X
M'dzina la Mulungu Wachifundo
Chambih Wachisoni.
l.Alif-Ldm-Rd. Izi ndi aya za
m'Buku lanzeru. (Lokamba
zanzeru zokhazokha).
2. Kodi nchodabwitsa kwa
anthu kuti Tamuvumbulutsira
(chivumbulutso) Munthu wa
mwaiwo (yemwe ndi
Muhammad{SAW}) kuti
achenjeze anthu Ndipowauza
nkhani yabwino Amene
akhulupirira kuti iwo adzapeza
Ulemelero waukulu kwa Mbuye
Wawo? Osakhulupirira adati:
"Ndithudi uyu ndi wa Matsenga
(mfiti) wowonekera". 1
3. Ndithu, Mbuye wanu ndi
Mulungu Amene adalenga thambo
ndi nthaka (Ndi zonse za
m'menemo) m'masiku Asanu ndi
limodzi; (masiku omwe Palibe
yemwe akuwadziwa kutalika
Kwake koma lye yekha), kenako
Adakhazikika pampando Wake
Wachifumu (kukhazikika kwake
Akukudziwa ndi lye yekha basi),
;'-.*V
o^t^t^u-
— Vtf
*£M&0&
L * 9 7 1711 \\ m9 ^ •• 9 ^ *
<&i%M&
Mulungu akuti, "Sikunayenere kwa anthu kudabwa ndi kutsutsa
chivumbulutso chathu kwa munthu wochokera mwa iwo yemwe cholinga
chake nkuti achenjeze anthu za chilango cha Mulungu ndi kuti awauze nkhani
zabwino amene mwa iwo akhulupirira. Ndiponso nkosayenera kwa iwo
kumunenera Muhammadi (SAW), Mtumiki wathu, kuti iye ndi wa matsenga".
Surat 10. Yiinus
Juzu 11
429
U fr>i
^ * <j^>3l 5 jJ-*»
Amayendetsa zinthu (za
Zolengedwa Zake.) Palibe
Muomboli (woombola wina) koma
Pambuyo pa chilolezo Chake
(Mulungu). Uyo ndiye Mulungu
Mbuye wanu; choncho
mupembedzeni lye. Kodi
simungakumbukire (Kuti
mafanowo si milungu)?
4. Kobwerera kwanu nonsenu
ndi kwa lye. Hi ndilonjezo la
Mulungu Loona. Ndithu, lye ndi
Yemwe Adayamba kulenga
(zolengedwa), ndiponso Ndi
Yemwe adzazibwereza (pambuyo
Pa imfa) kuti adzawalipire amene
Adakhulupirira ndi kumachita
Zabwino mwa chilungamo. Ndipo
Amene sadakhulupirire, akapeza
Zakumwa za madzi owira ndi
chilango Chopweteka chifukwa
cha Kusakhulupirira kwawo.
5. lye (Mulungu) ndi Yemwe
adapanga Dzuwa kukhala lowala,
ndi mwezi Kukhala wounika;
ndipo adaukonzera Mbuto
(masitesheni ) kuti Mudziwe
kuchuluka kwa zaka ndi
Chiwerengero chake. Mulungu
Sadalenge zimenezo koma
Mwachoonadi (ndi cholinga cha
nzeru). Akufotokoza aya (Zake)
kwa anthu Ozindikira. 1
Mbuye wanu ndi Yemwe adalenga thambo ndi nthaka. Ndipo dzuwa
adalipanga kuti lizipereka kuwala ku zolengedwa; naonso mwezi kuti
Siirat 10. Yunus
Juzu 11
430
\\ *jir\
^ * j^Ji *Jf
6. Ndithu, m'kusinthanasinthana
Kwa (nthawi zonse,) usiku ndi
Usana ndi zomwe Mulungu walenga
Kumwamba ndi pansi, ndithudi,
ndi Zisonyezo kwa anthu oopa.
7. Ndithu, amene saopa
kukumana Nafe, Nakondetsetsa
umoyo wapadziko Lapansi ndi
kukhazikika (mtima) Ndi za
mmenemo, ndi omwe akunyozera
Aya Zathu,
8. Iwowo (onse) malo awo ndi
kumoto Chifukwa cha zomwe
adazipeza (M'njira zosayenera).
9. Ndithu amene akhulupirira
ndi Kumachita zabwino,Mbuye
wawo Awaongola chifukwa cha
Chikhulupiriro cha wo; (adzalowa
m'minda Yamtendere) pansi ndi
Patsogolo pake mitsinje ikuyenda
M'minda yamtendere.
10. Mapemphero awo
m'menemo adzakhala Kunena:
"'SubuhanakaLahuma' Ulemerero
ndi wanu, O! Inu Ambuye
Mulungu!" Ndipo kulonjerana
Kwawo m'menemo kudzakhala
kunena: "'Salaam (alayikum')
Mtendere ukhale painu." Ndipo
uzitumiza kuunika. Ndipo mwezi adaupangira njira momwe umayenda. Ndipo
kuunika kwake kumakhala kosiyanasiyana chifukwa cha masitesheniwa. Izi
nkuti zikuthangateni powerengera nthawi, ndikuti mudziwe chiwerengero cha
zaka. Mulungu adalenga zimenezi ncholinga chanzeru zakuya.
Surat 10. Yunus
Juzu 11
431
\ > *>»
^ * cT'Ji 5 JJ~"
duwa yawo yomaliza (idzakhala
kuyamika Ponena kuti) "
' Alham'du Lillah Rabil a'lamin'.
Kuyamikidwa konse Nkwa
Mulungu Mbuyewa
zolengedwa." 1
1 1 . Ndipo Mulungu akadakhala
kuti akuwapatsa Anthu zoipa
mwachangu (zomwe iwo
akuzifulumizitsa) monga momwe
iwo Amafulumizitsira (kupeza)
zabwino (Ndiye kuti)
ikadalamulidwa nthawi yawo
( Yowaonongera koma Mulungu
amawamvera Chisoni) koma
amene saopa kukumana Nafe,
Tikuwasiya akuyumbayumba
m'zoipa Zawo.
12. Ndipo vuto likamkhuza
munthu Amatipempha
(m'kakhalidwe kake Konse),
chogona, chokhala kapena
Choimirira. Koma tikamchotsera
Vuto lomwe lidampeza, amayenda
ngati Sanatipempheko pa vuto
lomwe lidamkhudza Momwemo
ndimo Zakometseredwa kwa
opyola Malire zomwe ankachita.
Pemphero la okhulupirira lidzakhaia kumuyeretsa Mulungu kuzimene adali
kumunenera osakhulupirira pa dziko lapansi. Nayenso Mulungu adzakhala
akuwalonjera. Ndipo nawo adzakhala akulonjerananso wina ndi mnzake. Uku
nkutsimikizira mtendere ndi kukhazikika kopanda kutekeseka ndi china
chilichonse. Ndipo nthawi zonse kothera kwa mapemphero awo ndi kuthokoza
Mulungu powalimbikitsa pachikhulupiriro.
2 Munthu vuto likamkhudza mthupi mwake, kapena pachuma chake ndi
mwina motero apo mpomwe amazindikira za kufooka kwake. Amayamba
Surat 10. Yunus
Juzu 11
432
1 \ *>i
\ * u~jy~ *jy
13. Ndipo ndithu, tidaiononga
mibadwo Yambiri patsogolo panu
pamene Idachita zoipa. Komatu
atumiki Awo adawadzera ndi
zisonyezo Zoonekera, koma sadali
oti nkukhulupirira. Umo ndi
momwenso tidzawalipirire Anthu
ochita zoipa!
14. Kenako takupangani inu
(Asilamu) Kukhala olowa m'malo
mwawo Padziko pambuyo pawo
kuti tione mmene Mungachitire
(zabwino kapena zoipa).
15. Ndipo ay a zathu zomveka
bwino zikawerengedwa Kwa iwo,
akunena amene saopa Kukumana
ndi Ife, "Bwera ndi Qur'an
(Yogwirizana ndi zofuna zathu)
osati Iyi, kapena uyisinthe
(pang'ono)." Nena: "Nkosatheka
kwa ine kuisintha mwachifuniro
Changa. Sinditsata koma zimene
Zikuvumbulutsidwa kwa ine.
Ndithu, Ine ndikuopa chilango cha
tsiku lalikulu Ngati ndinyoza
Mbuye wanga."
16. Nena: " Mulungu akadafuna,
Sindikadakuwerengerani Qur'aniyi
%&%fati&$&
kumkuwira Mbuye wake Mulungu ndi kumpempha 'kakhalidwe kake konse-
chogona, chokhala, choimirira kuti amchotsere mliri umene wamgwera. Koma
Mulungu akamuyankha namchotsera vutolo amamfulatira Mulungu napitiriza
kumlakwira naiwala ubwino wa Mulungu ngati kuti vuto silidamkhudze, ngati
kutinso Mulungu sadampemphe konse. ichi ndicho chikhalidwe cha anthu
ambiri.Amadziwa Mulungu pomwe mavuto akawagwera. Koma akakhala
pamtendere Mulungu amamuiwala.
Surat 10. Yunus
Juzu 11
433
\\ *>i
^ • O^Ji ~ JJ**
Ndiponso sakadakudziwitsani
Qur'aniyo Ndidakhala pakati panu
moyo wanga (zaka Zambiri)
isadavumbulutsidwe
(Simudandimve ndikunena
chilichonse Cha utumiki). Kodi
mulibe nzeru?"
17. Ndani woipitsitsa woposa
yemwe Akumpekera Mulungu
bodza,ndi yemwe Akutsutsa aya
Zake? Ndithudi, Sangapambane
wochita zoipa.
18.Ndipo iwo akupembedza
milungu yina kusiya Mulungu,
yomwe singathe kuwapatsa
masautso (Ngati atasiya
kuipembedza) ndiponso Siyingathe
kuwapatsa chithandizo (ngati
Atalimbika kuipembedza) ndipo
akunena:"Iwo (Mafanowo) ndi
aomboli athu kwa Mulungu".
Nena: "Kodi mukumuuza
Mulungu zomwe sakudziwa
Kumwamba ndi pansi?
Wapatukana Mulungu Ndipo
watukuka kuzimene
akum'phatikiza nazo.
19. Ndipo ndithudi anthu kalero
(M'nthawi ya Adam) adali mpingo
Umodzi (opembedza Mulungu
M'modzi), Koma adasiyana
(pambuyo pake). Ndipo
pakadapanda liwu lochokera Kwa
Mbuye wako, lomwe lidatsogola
(Lakuti adzawalanga tsiku la
©(•y^P^I
Surat 10. Yunus
Juzu 11
434
n *>»
y * a^¥- 5 JJ-"
Kiyama), Ndithu,
kukadaweruzidwa pakati pawo
M'zomwe adali kusiyana. 1
20.Ndipo akunena: "Bwanji
sichidatsitsidwe Kwa iye
chizindikiro (chotsimikizira
Uneneri wake) chochokera Kwa
Mbuye wake (chomwe takhala
Tikuchipempha nthawi ndi
nthawi?") Nena (kwa i wo):
"Ndithu, kudziwa Zobisika nkwa
Mulungu yekha. Choncho dikirani
(chiweruzo cha Mulungu) inenso
pamodzi nanu ndine Mmodzi wa
odikira".
21. Ndipo tikawalawitsa anthu
Mtendere pambuyo pa masautso
omwe Adawakhudza, pompo iwo
amayamba Kuzichitira ndale aya
Zathu. Nena: "Mulungu
ngwachangu kwambiri Poononga
ndale (zawo)" Ndithu, Amithenga
athu (Angelo) akulemba Ziwembu
zanu (zonse) zimene mukuchita.
22. Iye ndi Yemwe
amakuyendetsani Pamtunda ndi
panyanja; kufikira Pom we
aj^^oSSIM»
9 9 S9" 'XL
Ndithudi, anthu mchilengedwe chawo adali a mpingo umodzi wogonjera
Mulungu mwa chilengedwe. Kenako Mulungu adawatumizira aneneri kuti
awatsogolere kunjira Yake molingana ndi chilamulo chake Mulungu. Koma
ngakhale zili tere anthu adali ndi ufulu mwa chilengedwe chawo kulandira
choipa kapena chabwino. Potero, choipa chidawagonjetsa ena a iwo natsata
zilakolako za satana.nasiyana ndi anzawo chifukwa chazimenezo. Komatu
padali lamulo la Mulungu la pachiyambi loti oipa sadzawalanga mwachangu
koma kufikira nthawi yawo itakwana. Pakadapanda lamuloli ndiye kuti onse
akadawalanga nthawi yomweyo.
Surat 10. Yunus
Juzu 11
435
n *>i
^ * tHji 5 JJ~*
mumakhala m'zombo; ndipo
Zimayenda nawo (zombozo) ndi
Mphepo yabwino, naisangalalira.
(Mwadzidzidzi) namondwe
Nkuzidzera (zombozo) ndipo
Mafunde nkuwadzera mbali zonse
Natsimikiza kuti azingidwa (ndi
Chionongeko); amampempha
Mulungu modzipereka Kwa lye
mukupempha kwawo (uku
Akunena): "Ngati mutipulumutsa
Pa ichi, tidzakhala m'gulu la
Oyamika (nthawi zonse)!"
23. Koma akawapulumutsa,
pompo akuyamba Kudzitukumula
ndi kuononga padziko Popanda
chowayenereza (kutero). E inu
anthu! Kuononga kwanu
Kukubweretserani masautso inu
Nokha. Ndipo chisangalalo (chake)
Chamoyo wadziko lapansi
(nchochepa). Kenako kobwerera
kwanu ndi kwa Ife, Ndipo
tidzakuuzani zomwe munkachita.
24. Ndithu, fanizo la moyo
wadziko Lapansi lili ngati madzi
amvula Tawatsitsa kuchokera
kumitambo nkusakanikirana Ndi
zomera zam'nthaka zomwe Anthu
ndi nyama amadya; kufikira
Nthaka ikakwaniritsa kukongola
Kwake ndi kudzikometsa ndipo eni
(Nthaka) nkuganiza kuti iwo ali
Ndi mphamvu panthakayo
(pokolola Zomwe zili pamenepo).
O-oJ
Surat 10. Yunus
Juzu 11
436
U *>»
^ • j~*ji *jj-»
Mwadzidzidzi Nkuzidzera lamulo
Lathu (zapanthakazo), Usiku
kapena masana, nkuzichita
Kukhala ngati zokololedwa ngati
Kuti sizidalipo dzulo (lake).
Motere tikufotokoza aya kwa
anthu Olingalira.
25. Ndipo Mulungu akuitanira
(anthu Ake) kunyumba
yamtendere.Ndipo
Amamuongolera kunjira yolunjika
Amene wamfuna (ngati ali
wotheka Kuongoka).
26. Ndipo omwe achita
zabwino, adzapata (Malipiro)
abwino ndi zoonjezera. Ndipo
fumbi silikavindikira nkhope
Zawo. Ndiponso kunyozeka
Sikukawapeza. Iwowo ndiwo
anthu A ku Munda wa Mtendere;
mmenemo Akakhala muyaya.
27. Ndipo amene akolola zoipa
(kuchokera M'zochita zawo zoipa)
mphoto ya Choipa ndiyofanana ndi
icho; Ndipo kunyozeka
kudzawapeza; Sadzakhala ndi
aliyense wotha Kuwateteza
kuchilango cha Mulungu. Nkhope
zawo zidzakhala ngati
Zaphimbidwa ndi zidutswa za
Usiku wa m'dima, (zidzakhala
Zakuda kwambiri); awo ndiwo
anthu Akumoto. I wo mmenemo
adzakhala Muyaya.
%;mm
GQ\\LK\'-L
Siirat 10. Yunus
Juzu 11
437
>\ *>i
^ * U^Ji 5 JJ~"
28. Ndipo (akumbutse za) tsiku
lomwe Tidzawasonkhanitsa onse.
Kenako Tidzawauza amene
ankaphatikiza Mulungu (kuti):
"Imani pompo inu Pamodzi ndi
aphatikizi anuwo". Ndipo
tidzawasiyanitsa pakati pawo;
Koma aphatikizi awowo adzati:
"Simudali kutipembedza ife
(Koma mudali kupembedza
Zilakolako zanu).
29. "Mulungu akukwanira
kukhala mboni Pakati pathu ndi
pakati panu. Ndithu, ife sitidali
kuzindikira Za mapemphero anu.
(Sitinkazindikira Kuti inu
mukutipembedza)"
30. Kumeneko munthu aliyense
adzadziwa Zimene adatsogoza;
ndipo adzabwezedwa Kwa
Mulungu, Mbuye wawo Woona
Ndipo zidzawasowa zimene adali
Kupeka.
31.Nena: "Kodi ndani
akukupatsani (Zopatsa) kuchokera
kumwamba (Povumbwitsa mvula),
ndi pansi (Pomeretsa mmera)?
Nanga Ndani amakupatsani kumva
ndi Kupenya? Nanga ndani amene
Akutulutsa chamoyo kuchokera
m'chakufa, Ndi kutulutsa chakufa
m'chamoyo? Nanga ndani
akukonza zinthu zonse?" Anena:
"Ndi Mulungu." Choncho, Nena:
"Kodi bwanji Simukumuopa?"
Surat 10. Yunus
Juzu 11
438 1 > *>*
\ • cT^Ji ^J" -
32. Uyo ndi Mulungu, Mbuye
wanu Woona; Nanga pali chiyani
Pambuyo poleka choonadi,
Sikusokera basi? Kodi nanga
Mukutembenuzidwa chotani
(kusiya Choonadi)?
33. Momwemo liwu la Mbuye
wako Latsimikizika kwa amene
Adatuluka m'chilamulo cha
Mulungu kuti iwo
sadzakhulupirira.
34. Nena: "Kodi alipo mwa
amene Mukuwaphatikiza ndi
Mulungu Amene angayambitse
kulenga Zolengedwa; kenako
(Zitafa) ndikuzibweza?" Nena:
"Mulungu ndi Yemwe
akuyambitsa Zolengedwa kenaka
ndi kuzibweza (Pambuyo
poonongeka). Nanga
mukutembenuzidwa chotani
(Kusiya chikhulupiriro)?
35. Nena: "Kodi alipo mwa
amene Mukuwaphatikiza ndi
Mulungu, Woongolera
kuchoonadi?" Nena: "Mulungu ndi
Yemwe Akuongolera kuchoonadi.
Kodi Amene akutsogolera
kuchoonadi Sindiye woyenera
kwambiri Kutsatidwa kapena
(woyenera Kutsatidwa ndi) yemwe
sakutha Kudziongola pokhapokha
atawongoledwa ndi Wina wake?
Nanga mwatani kodi?
Mukuweruza
*- "-&$&$
eQff'"*
Surat 10. Yunus
Juzu 11
439
\\ *>!
^ * U^Ji 5 JJ"*'
36. Ndipo ambiri a iwo satsatira
(China) koma zoganizira basi,
(Osati chomwe afufuza
ndikuchizindikira Ndi nzeru
zawo). Ndithu Choganizira
sichithandiza Ngakhale pang'ono
ku Choonadi. Ndithu, Mulungu
akudziwa Zonse zimene akuchita.
37. Ndipo sikotheka Qur'an iyi
Kukhala yopekedwa, yosachokera
Kwa Mulungu (monga momwe
Munenera). Koma (yachokera Kwa
Mulungu) kutsimikizira Zomwe
zidalipo patsogolo pake, Ndi
kulongosola za Mabuku (Akale).
Palibe chikaiko m'menemo (Kuti)
yachokera kwa Mbuye wa
Zolengedwa.
38. Kapena akunena kuti
waipeka? Nena: "Tabwerani ndi
Sura (imodzi) Yofanana ndi iyo,
ndipo itanani Amene mungathe
(kuwaitana kuti Akuthandizeni)
kupatula Mulungu, Ngati inu
mukunena zoona (kuti Qur'aniyi
waipeka Muhammad {SAW})."
39. Koma atsutsa zomwe
sakuzizindikira (M'mene zilili)
ngakhale tanthauzo lake (Lakuona
kwake kapena kunama kwake)
Lisanawafikebe. Momwemonso
adatsutsa Omwe adalipo patsogolo
pawo. Choncho, taona momwe
mathero A anthu ochimwa adalili.
Surat 10. Yunus
Juzu 11
440
U frjJrl
^ * jr^3i 5 jJ-*»
40. Ndipo mwa iwo pali ena
omwe Akuikhulupirira (Qur'an),
ndipo ena mwa iwo
Sakuikhulupirira. Ndipo Mbuye
Wako akuwadziwa bwino
oononga.
4 1. Ndipo ngati apitiriza
kukutsutsa, nena: "Ine ndiri ndi
ntchito yangajnunso muli ndi
ntchito yanu. Inu mwatalikirana
nazo zimene Ndikuchita, inenso
ndatalikirana nazo Zimene
mukuchita!"
42. Ndipo mwa iwo alipo ena
amene akumvetsera Kwa iwe,
(koma osati ndi Cholinga choti
adziwe). Kodi Iwe ungathe
kuwamveretsa agonthi,
Chikhalirecho nzeru alibe?
43. Ndipo alipo ena mwa iwo
Amene akukutong'olera Maso
(kukuyang'ana Monyoza). Kodi
iwe ungathe Kuwatsogolera
akhungu, Chikhalirecho sali
openya?
44. Ndithu, Mulungu sachitira
anthu Choipa chilichonse. Koma
anthu Akudzichitira okha zoipa.
(Adapatsidwa nzeru, koma
Sazigwiritsa ntchito).
45. Ndipo (akumbutse za) tsiku
lomwe Adzawasonkhanitsa (onse)
ngati Kuti sadakhale (padziko
lapansi) Koma ola limodzi la usana
S9.&' ' 9 £9?'" ' 9K"\*" \'^\\
Siirat 10. Yunus
Juzu 11
441
\\ *>i
L^y 'm-*
(Atathedwa nzeru).
Adzazindikirana Pakati pawo;
(koma aliyense Sadzalabadira
mnzake). Ndithu, Aonongeka
amene adatsutsa za Kukumana ndi
Mulungu Ndipo sadali oongoka.
46. Ndipo ngati tingakusonyeze
(pompano Padziko lapansi) zina
mwa Zomwe tikuwalonjeza
ndikuwachenjeza Nazo, kapena
kukubweretsera Imfa (usadazione
zimenezo), Kobwerera kwawo
nkwa Ife basi. Kenako Mulungu
ndi mboni pa Zomwe akuchita.
47. Ndipo fuko lililonse lili ndi
Mtumiki Ndipo akazabwera
Mtumiki Wawo (tsiku la
chiweruzo) Kudzaweruzidwa
pakati Pawo mwachilungamo
Ndipo sadzaponderezedwa.
48. Ndipo akunena
(osakhulupirira): "Kodi Lonjezo ili
lidzachitika liti Ngati mukunena
zoona?"
49. Nena: "Ndilibe mphamvu
mwandekha pa (Kudzichotsera)
vuto ngakhale (Kudzibweretsera)
thandizo. (Nanga za zimenezo
ndingadziweponji)? Koma
chimene Mulungu wafuna (ndi
Chomwe chimachitika). M 5 bad wo
uli Wonse uli ndi nthawi yake
(yofera). Nthawi yawo (yofera)
ikadza Sangathe kuichedwera ola
limodzi Ngakhale kufulumira."
«^0^Ai$yST
&&<jc$\J%&j%
a#a&*r«K&2
Surat 10. Yiinus
Juzu 11
442
\\ *>!
^ * cHji 5 J>"
50. Nena: "Kodi mukuona
bwanji, ngati Chilango Chakecho
chitakudzerani Usiku kapena usana
(mungathe Kuthawa)? Nanga
bwanji ochimwa
Akuchifulumizitsa (kuti chidze
Mwachangu)?
51. "Kodi chikadza ndi pamene
Mudzachikhulupirire?"
(Panthawiyo mudzauzidwa): "Kodi
tsopano (ndi pamene
Mukukhulupirira), chikhalirecho
Mudali kuchifulumizitsa (kale)?"
52. Kenako kudzanenedwa kwa
amene Adachita zoipa: "Lawani
chilango Chamuyaya! Kodi
mungalipidwe Zina osakhala
zomwe mudazipata (kuchokera
m'zochita zanu Zoipa)!"
53. Eti akukufunsa: "Kodi
nzoona Izo (zimene ukunena)?"
Nena: "Inde! ndikulumbira kwa
Mbuye Wanga, zimenezo ndi
zoona. Ndipo inu simungathe
kulepheretsa (Mulungu)."
54. Ndipo kukadakhala kuti
munthu Aliyense amene adachita
zoipa, Nkukhala nazo zonse
zam'dziko Akadapereka zonse kuti
adziombole Nazo (pamene
adzaona kuopsa kwa Chilango cha
tsikulo). Ndipo Akadzachiona
chilango, adzayesetsa Kubisa
madandaulo (awo; koma
Surat 10. Yunus
Juzu 11
443
U *>»
^ * cT^Ji 5 JJ-°
Adzaonekera poyera).Ndipo
kudzaweruzidwa Mwachilungamo
pakati pawo, ndipo Iwo
sadzaponderezedwa.
55. Tamverani! Ndithu, zonse
Zakumwamba ndipansi nza
Mulungu. Tamverani! Ndithu,
lonjezo la Mulungu ndi loona.
Koma ambiri a Iwo sadziwa.
56. lye (Mulungu ndi amene)
amapereka Moyo ndi imfa. Ndipo
kwa lye (Nonsenu)
mudzabwezedwa.
57. E inu anthuINdithu, ulaliki
Wakudzerani kuchokera kwa
Mbuye Wanu ndi chochiritsa
zomwe (matenda) Zili m'mitima
mwanu, Ndiponso nchiongoko ndi
chifundo Kwa okhulupirira.
58. Nena: "Chifukwa cha
ubwino wa Mulungu ndi chifundo
Chake, (Mwapeza zimenezi),
choncho Asangalalire zimenezi."
Izi Ndizabwino kwambiri kuposa
Zimene akusonkhanitsa (m'zinthu
Za dziko lapansi).
59. Nena: "Kodi mukuona
bwanji, Riziki lomwe Mulungu
wakutsitsirani? Kenako inu Una
mwa ilo mwalichita kukhala
Loletsedwa (la haramu), ndipo
lina mwa ilo Kukhala lololedwa (la
halali)." Nena: "Kodi Mulungu
adakulolezani (Kuchita zimenezo),
s^'it*-'
Surat 10. Yunus
Juzu 11
444
U *j*-i
U^3i d Ji-
kapena mukumpekera Mulungu
bodza?"
60. Kodi ali ndi ganizo lotani
amene Akumpekera Mulungu
bodza pa za Tsiku la Kiyama?
Ndithu, Mulungu Ndi Mwini
ubwino wochuluka kwa Anthu.
Koma ambiri aiwo Sathokoza.
61.Ndipo siutanganidwa ndi
ntchito Iliyonse, ndiponso
simuwerenga M'menemo (chinthu
chilichonse) Cha m'Qur'an ndipo
simuchita Ntchito ina iliyonse (inu
anthu) Koma Ife timakhala mboni
pa Inu pamene mukutanganidwa
nayo. Ndipo sichibisika kwa
Mbuye Wako chinthu chilichonse
ngakhale Cholemera ngati nyerere,
m'nthaka Ngakhale kumwamba.
Ndipo ngakhale Chocheperapo
zedi kuposa pamenepo Kapena
chokulirapo koma chili M'Buku
(la Mulungu) lofotokoza
Chilichonse.
62. Tamverani! Ndithu,
okondedwa A Mulungu sadzakhala
ndi mantha (Pa tsiku la
Kiyama),ndipo Sadzadandaula;
63. (Amenewo ndi) amene
Adakhulupirira Ndi kumuopa
Mulungu;
64. Iwo ali ndi zabwino pamoyo
wadziko Lapansi ndi pa tsiku
lomaliza. Palibe kusintha pa mawu
®
T V A<V.
Surat 10. Yunus
Juzu 11
445
\\ *>i
LT^y- °jj^
a Mulungu. Uku ndiko kupambana
Kwakukulu.
65. Ndipo (iwe,
Mtumiki{SAW})
Zisakudandaulitse zonena zawo
(zomwe Akukunenera monyoza).
Ndithu, ulemerero Ndi mphamvu
zonse nza Mulungu. lye
Ngwakumva, Ngodziwa.
66. Tamverani! Ndithu,(zonse)
Zakumwamba ndi zapansi, nza
Mulungu. Ndipo amene
akupembedza Zina kusiya
Mulungu, Satsatira aphatikizi (a
Mulungu), Akungotsatira
zoganizira. Ndipo iwo sanena
china Koma bodza basi.
67. lye (Mulungu) ndi Yemwe
adakupangirani Usiku kuti
muzipumamo. Ndipo
(adakupangirani) usana kukhala
Wowala (kuti mupenye). Ndithu,
M'zimenezo muli zisonyezo
(Zosonyeza chifundo cha Mulungu
Pazolengedwa Zake) kwa anthu
Akumva.
68. Akunena: "Mulungu
wadzipangira Mwana" wapatukana
ndi zimenezo! lye Ngokwanira,
(Salakalaka Mwana ngakhale
mthangati aliyense). Ndi zake
(zonse) zakumwamba ndi zapansi.
Inu mulibe umboni pazimenezi.
Kodi Mukumnenera Mulungu
zomwe Simukuzidzidwa?
kfl&fSk
©
Surat 10. Yiinus
Juzu 11
446
n *>i
LT'Ji *JJ"
69. Nena: "Ndithu, amene
Akumpekera Mulungu Bodza,
sadzapambana".
70. Ndichisangalalo chochepa
basi M'dziko lapansi.Kenako kwa
Ife ndiwo mabwerero awo. Kenako
tidzawalawitsa chilango Chaukali
chifukwa cha kusakhulupirira
Kwawo.
71. Ndipo awerengere
(molakatula) nkhani za Nuhi
pamene adanena kwa anthu ake,
"E inu anthu anga! Ngati kukhala
Kwanga pamodzi ndi inu ndi
Kukumbutsa kwanga aya za
Mulungu Kukunyansani, ine
ndatsamira kwa Mulungu
(sindisiya ntchito yangayi). Inunso
sonkhanitsani zinthu zanu Pamodzi
ndi milungu yanuyo; (Sonkhanani
kuti mundichitire choipa, Ine
sindilabadira chilichonse). Ndipo
Chinthu chanucho chisabisike kwa
inu, (Chitani moonekera. Ine
sinditekeseka Ndi chilichonse).
Kenako chitani pa ine (Chimene
mufuna kuchita) ndipo
Musandipatse danga.
72. Ngati mutembenuka ndi
kunyoza, (Ndikufuna kwanu).Ine
sindinakupempheni Malipiro .
Malipiro anga kulibe Kulikonse
(kumene ndingalandire) Koma
kwa Mulungu, ndipo
®&££\
Surat 10. Yunus
Juzu 11
447
U *>)
\ ♦ j-Jji 5jj-»
Ndalamulidwa kuti ndikhale
Mmodzi wa ogonjera lye".
73. Koma adamutsutsa.
Choncho Tidampulumutsa
pamodzi ndi Amene adali naye
m'chombo. Ndipo tidawasankha
iwo kukhala Otsala (padziko
anzawo ataonongeka). Ndipo
tidawamiza amene adatsutsa aya
Zathu. Taona momwe mapeto A
ochenjezedwa adalili!
74. Pambuyo pake tidawatumiza
Atumiki Ambiri kwa anthu awo.
Adawadzera Ndi mitsutso
(zisonyezo) yoonekera Poyera
koma sadali okhulupirira zimene
Ena adazitsutsa kale,(adatsatira
Njira zomwezo za anzawo). Umo
ndi momwe Tikudindira zidindo
m'mitima ya anthu Opyola malire.
75. Pambuyo pawo tidamtuma
Musa ndi Haaruna pamodzi ndi
zizindikiro zathu kwa Farawo ndi
nduna zake. Koma adadzikweza.
Tero adali anthu oipa.
76. Ndipo pamene choonadi
chidawadzera Kuchokera kwa Ife,
adanena: "Ndithu, Awa ndi
matsenga oonekera."
77. Musa adati: "Mukutero
pachoonadi Pamene chakudzerani?
Kodi matsenga ali Chonchi?
(Bwanji ichi chapambana)? Ndipo
Surat 10. Yiinus
Juzu 11
448
n *>■!
\ « ^pjji «jj~-
amatsenga sangapambane
(Ngakhale zitatani)"
78. (Iwo) adati: "Kodi
watidzera kuti Utichotse kuzimene
tidawapeza nazo Makolo athu kuti
ukulu ukhale wa inu (Awiri)
mdzikoli? Koma ife
Sitingakukhulupirireni awirinu."
79. Ndipo Farawo adati:
"Ndibweretsereni Wamatsenga
aliyense wodziwa Kwambiri
(zamatsenga)."
80. Ndipo pamene amatsenga
adadza, Musa adati kwa iwo:
"Ponyani Zomwe mufuna kuponya
(Kuti musonyeze ukatswiri Wanu
kwa anthu)".
81. Pamene adaponya, Musa
adati: "Zomwe mwabweretsa ndi
matsenga. Mulungu awaononga
pompano. Ndithu, Mulungu
Sakonza ntchito Za oononga.
82. Ndipo Mulungu
achilimbikitsa Choonadi ndi mau
Ake, ngakhale Oipa anyansidwe
nazo".
83. Sadamkhulupirire Musa
kupatula Anyamata a mwa anthu
ake, chifukwa Choopa Farawo ndi
nduna zake kuti Angawazunze.
Ndithu, Farawo adali Wodzikuza
padziko, ndithudi, adali M'modzi
mwa opyola malire.
a^Q&$I^M@b
w
Surat 10. Yunus
Juzu 11
449 1 1 > *j*-»
^ * c/^Ji 5 J>^
84. Ndipo Musa adati: "E inu
anthu Anga! Ngati inu
mwakhulupirira Mulungu,
choncho tsamirani kwa lye Ngati
mulidi Asilarnu (oona).
85. (I wo) adati: "Tayadzarnira
kwa Mulungu. O Mbuye wathu!
Musatichite kukhala Ozunzidwa
ndi anthu oipa.
86. Ndipo tipulumutseni Mwa
chifundo Chanu ku anthu
Osakhulupirira."
87. Ndipo tidavumbulutsa kwa
Musa ndi M'bale wake mawu
Athu (oti): "Apangireni nyumba
anthu anu mu Eguputo ndipo
nyumba zanu zichiteni Kukhala
misikiti (pakuti simungathe
Kukhala ndi misikiti yoonekera),
Ndipo pempherani Swala. Ndipo
auze Nkhani yabwino okhulupirira
(kuti Mulungu awapatsa zabwino
pamoyo Wadziko lapansi ndi
patsiku lomaliza)."
88. Ndipo Musa adati: "Mbuye
wathu! Inu mwampatsa Farawo ndi
nduna zake Zodzikometsera, ndi
chuma chambirimbiri Pamoyo
wapadziko. Mbuye wathu,
Choncho iwo akusokeretsa anthu
pa Njira yanu. Mbuye wathu,
wonongani Chuma chawo ndipo
iumitseni mitima Yawo popeza
sakhulupirira kufikira Ataona
chilango chowawa."
"b
*%jJH\J&fitf&
®r,'i3>.
Surat 10. Yunus
Juzu 11
450
U *>»
^ * U^Ji ~ d JJ~*
89. (Mulungu) adati: "Pempho
Lanu lavomerezedwa! Choncho
lungamani Mwaubwino, musatsate
njira za omwe Sadziwa."
90. Ndipo tidawaolotsa
panyanja ana a Israeli. Ndipo
Farawo ndi asilikali Ake ankhondo
adawatsata moipitsa ndi
Mwamtopola, kufikira pamene
kumira Kudampeza; (iye) adati:
"Ndakhulupirira Kuti palibe
wopembedzedwa mwachoonadi
Koma yemwe ana a Israeli
amkhulupirira. Ndipo ine ndine
mmodzi mwa Omugonjera (monga
iwo akumgonjera)."
91. (Angelo adamuuza kuti:)
"Tsopano (Ndi pamene
ukukhulupirira), pomwe Kale
udanyoza ndikukhala mmodzi
Waoononga!"
92. "Choncho lero
tikupulumutsa (polisunga) Thupi
lako, kuti ukhale chisonyezo kwa
Amene akudza m'mbuyo mwako
(kuti adziwe Kuti sudali Mulungu).
Koma ndithu, Anthu ambiri
salabadira zisonyezo Zathu."
93. Ndipo (pambuyo pake)
tidawakonzera Mokhala
mwabwino ana a Israeli,
Ndikuwapatsa zabwino.
Sadasiyane Kufikira pamene nzeru
zidawadzera. Ndithu, Mbuye wako
***<a$$Z&$*s
Surat 10. Yunus
Juzu 11
451
U frj*-*
u*y-*jy*
adzaweruza pakati Pawo tsiku la
Kiyama pazimene adali
Kutsutsana.
94. Ngati uli ndi chipeneko
pazimene Takuvumbulutsira,
afunse amene akuwerenga Mabuku
akale (Ayuda ndi Akhrisitu Amene
alowa m'Chisilamu). Ndithu,
Choonadi chakufika kuchokera
kwa Mbuye wako. Choncho
usakhale mwa Amene akukaikira.
95. Ndiponso usakhale mwa
omwe akutsutsa Zizindikiro za
Mulungu, kuopa kuti
Ungadzakhale m'gulu la.otaika.
96. Ndithu, aja amene liwu la
Mbuye wako latsimikizika pa iwo,
Sakhulupirira.
97. Ndipo ngakhale kuti
chisonyezo chamtundu Uliwonse
chiwadzere, mpaka aone Chilango
chopweteka.
98. Kodi udalipo mudzi (ndi
umodzi womwe Pakati pamidzi
mwa yomwe tidaiwononga),
Umene udalapa ndi kukhulupirira
(Pambuyo poona chilango kotero
kuti) Chikhulupiriro chake
nkuuthandiza Panthawi imeneyo,
osati kupatula anthu a Yunus
okha? (Ndi anthu a Yunus okha
Amene adakhulupirira pamene
adazindikira Za chilango kuti
chikudza. Choncho
bs
sua
Siirat 10. Yunus
Juzu 11
452
U *>l
^Ji °JJ^
Adapulumuka). Pamene
adakhulupirira, Tidawachotsera
chilango choyalutsa M'moyo
wapadziko lapansi, ndipo
Tidawasangalatsa kufikira nthawi
yawo (Yofera).
99. Ndipo Mbuye wako
akadafuna (kuwakakamiza anthu
Mwamphamvu kuti akhulupirire),
onse ali Mdziko lapansi
akadakhulupirira (Sipakadatsala
ndi mmodzi yemwe. Koma
Mulungu safuna kukakamiza anthu
Mwamphamvu). Nanga kodi iwe
uwakakamiza Anthu kuti akhale
okhulupirira.
100. Ndipo palibe munthu
angakhulupirire Popanda chilolezo
cha Mulungu. lye Amaachitira
ukali amene alibe Nzeru (amene
sagwiritsa Ntchito nzeru zawo).
lOl.Nena: "Yang'anani
nchiyani chikupezeka Kumwamba
ndi pansi!" Ndipo zisonyezo
Zonsezi ndi machenjezo onsewa
Sangawakwanire (ndi
kuwapindulira Kanthu) anthu
osakhulupirira.
102. Kodi chiliponso chimene
akudikira Osakhala (kuwadzera)
monga masiku (Azilango zomwe
zidawapeza) amene Adapita kale
(iwo asadafike)? Nena: "Dikirani
nanenso ndili Pamodzi nanu mwa
odikira."
% t
<" L~? 9 fl '*
b*
v>
Surat 10. Yunus
Juzu 11
453 I * > *>»
U**M *Jf
103. Kenako tidzawapulumutsa
aneneri Athu ndi amene
adakhulupirira. Chotere nkoyenera
kwa Ife kuwapulumutsa
Okhulupirira.
104.Nena: "E inu anthu! Ngati
inu muli Ndi chipeneko pa
chipembedzo changa, (Dziwani
kuti) sindingapembedze zimene
Mukuzipembedza kusiya
Mulungu; Koma Ine ndipembedza
Mulungu (Mmodzi yekha) Yemwe
amakupatsani imfa (ndi moyo).
Ndipo ndalamulidwa kukhala
mmodzi wa Okhulupirira,
lOS.Ndiponso (ndauzidwa
kuti): 'Lungamitsa nkhope yako
kuchipembedzo Momuyeretsera
Mulungu mapemphero Ake, Ndipo
usakhale mmodzi mwa ophatikiza
Mulungu ndi zinthu zina;
106. Ndipo (kuti), usapembedze
chimene Sichingakupindulitsire
zabwino, kapena Kukubweretsera
masautso, kusiya Mulungu. Ngati
utero ndiye kuti iwe ndi mmodzi
Wa oipa."
107. Ndipo ngati Mulungu
atakukhudza ndi masautso, Palibe
aliyense owachotsa kupatula lye.
Ngatinso atakufunira
zabwino,palibe Amene
angaubweze ubwino Wake. (lye)
Amadza ndi ubwinowo kwa amene
<%
Surat 10. Yunus
Juzu 11 454 > > tjJr
^ % cT^Ji *Jf
wamfuna Mwa akapolo Ake.
Ndipo lye Ngokhululuka
Ngwachisoni .
108.Nena:"E inu
anthuIChoonadi chakudzerani
Kuchokera kwa Mbuye wanu.
Choncho amene Waongoka,
(zabwino zake) zili pa iye mwini.
Ndipo amene wasokera, ndithu
zotsatira Zakusokera zili pa iye
mwini. Ndipo ine Sindili
muyang'aniri pa inu, (udindo
wanga Ndi kuchenjeza basi)"
109. Ndipo (andiuza kuti):
"Tsatira zimene
Zikuvumbulutsidwa kwa iwe
ndipo pirira Kufikira Mulungu
adzaweruze. Iye Ngoweruza bwino
kuposa aweruzi onse."
«y«
Suratll.Hud
Juzu 11
455
n *>i
^ S ijA 5jj**>
Stoat Hud XI
*
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Alif-Lam-Ra. Hi ndi buku
lomwe ndime Zake zakonzedwa
bwino ndipo zafotokozedwa
Mwatsatanetsatane kuchokera kwa
Mulungu Mwini nzeru zakuya
Wodziwa chilichonse.
2. (Wachita zimenezi) kuti
musampembedze wina Wake
koma Mulungu yekha. Ndithudi
ine kwa inu Ndi mchenjezi
wochokera kwa lye ndiponso
Wokuuzani nkhani zabwino .
3. Ndikuti mupemphe
chikhululuko kwa Mbuye wanu
Ndipo mulape kwa lye.
Akupatsani chisangalalo Chabwino
mpakana m'nthawi idaikidwa.
Ndipo adzampatsa (tsiku
lachimaliziro) aliyense Wochita za
ufulu, ufulu wake. Koma, ngati
Mupotoka ine kwanga
nkukuoperani za Chilango cha
tsiku lalikulu.
4. Kobwerera kwanu nkwa
Mulungu basi. lye ali Ndi
mphamvu pa chilichonse.
5. Tamverani! Iwo akubisa
zimene zili m'mitima Yawo kuti
amubise lye (Mulungu). Mverani!
o^j)t^j)l*kU-
-^
Su i at 11. 1 hid
Juzu 12
456 > t >>>
> > i^A 6jj~>
Ndithudi pamene akuzifunda nsalu
Zawo lye akudziwa zimene
akuzibisa ndi Zimene akuzionetsa.
Ndithudi lye ndiwodziwa Za
mzifuwa.
6. Ndipo palibe nyama iliyonse
(cholengedwa Chilichonse)
panthaka koma riziki lake Lili kwa
Mulungu; Ndipo (lye) akudziwa
Mbuto yake yamuyaya ndi mbuto
yake Yakungodutsapo (yomwe ndi
pano padziko Lapansi). Zonse zili
m'buku lofotokoza Chilichonse. 1
7. Ndipo lye ndi Yemwe
adalenga Thambo ndi nthaka
M'masiku asanu ndi limodzi,
ndipo Mpando Wake wachifumu
udali Pamadzi. (Adakulengani)
Kuti akuyeseni mayeso, ndani
mwa inu ali Wochita zabwino.
Koma ukanena (kwa Iwo kuti):
"Inu mudzaukitsidwa pambuyo Pa
imfa," Amene sadakhulupirire
akuti, "Izi sikanthu koma ndi
matsenga oonekera. 2
8. Ndipo ngati
titawachedwetsera chilango Mpaka
ymd$&®g$z
%
p\&6a\%&&tys
Mawu oti "Riziki lake lili kwa Mulungu" nkuti Mulungu wapatsa chilichonse
mphamvu zofunira riziki lake (zoyendetsa moyo wake). Ndimeyi siitanthauza
kuti munthu angokhala popanda kugwira ntchito nayembekezera kuti riziki
lichokera kumwamba. Koma munthu agwire ntchito molimbikira kuti apeze
chuma cha Mulungu. Zotere nzimene Qur'an ikutilangiza.
2 Kunena kwakuti thambo ndi nthaka zidalengedwa m'masiku asanu ndi
limodzi, amene akudziwa za masiku asanu ndi limodziwo momwe adalili ndi
Mulungu yekha. Ndiponso mpandowo sitikudziwa tsatanetsatane
wake.Chimene chilipo kwa ife nkukhulupirira basi.
Suratll.Hud
Juzu 12
457
M *>i
S \ SjJb 5j^-»
m'nthawi yodziwika (ndi
kukhazikitsidwa ndi Ife), akunena
(mwamwano): "Nchiyani
chikumanga chilangocho (kuti
Chidze)? "Tamverani! Tsiku
lomwe Chidzawadzera,
sichidzachotsedwa kwa iwo Ndipo
zomwe adali kuzichita
mwachibwana Zidzawazinga.
9. Ndipo munthu tikamulawitsa
mtendere Wochokera kwa Ife,
kenako nkuuchotsa Kwa iye,
ndithu, amakhala wotaya mtima
Kwambiri ndikukhala
wosathokoza.
10. Koma ngati titamulawitsa
mtendere Pambuyo pa masautso
omwe adamkhudza, Amati:
"Masautso andichoka,"(ndipo
Sakhala wotanganidwa ndi ntchito
Zabwino zosonyeza kuyamika
Mulungu), Choncho (tsopano)
amakhala wosangalala
11. Koma amene apirira ndi
Kumachita ntchito zabwino,
iwowo Ndiwo adzapeza
chikhululuko Ndi malipiro aakulu
(kwa Mulungu).
12. Mwina usiya zina mwa
zomwe Zikuvumbulutsidwa kwa
iwe ndikubanika Nazo mchifuwa
mwako chifukwa Chakuti
akunena: "Bwanji sizidatsitsidwe
Kwa iye nkhokwe zachuma kapena
^
Sural 11. Hud
Juzu 12
458
U *;*■»
^ ^ ^ a^j-*
bwanji Mngelo osadza pamodzi
ndi iye?" Koma ndithu, iwe ndiwe
mchenjezi Basi ndipo Mulungu
ndiye Muyang'aniri Wachinthu
chilichonse. {
13. Kapena akunena kuti:
"Waipeka Qur'an?" Nena:
"Tabweretsani Sura Khumi
zopekedwa zomwe Zingafanane
ndi iyi (Qur'an) ndipo aitaneni
amene Mungathe (kuwaitana)
kupatula Mulungu. (Adze
akuthandizeni kulemba Bukulo)
Ngati mukunena zoona!"
14. "Ngati sakuyankhani,
choncho, dziwani Kuti
lavumbulutsidwa M'kudziwa kwa
Mulungu, Ndikuti kulibe Mulungu
wina koma Iye. Nanga kodi inu
simugonjera Iye?"
15. Amene akufuna moyo
wadziko lapansi Ndi zokometsera
zake, tiwapatsa pompo Padziko
lapansi (malipiro a) zochita Zawo
mokwanira, ndipo iwo m'menemo
Sachepetseredwa chilichonse.
16. Iwo ndi omwe sadzakhala
ndi kanthu tsiku La chimaliziro
koma moto basi. Ndipo Zimene
Ophatikiza Mulungu ndi zina zake adali kupereka maganjzo kwa Mtumiki
akuti ampemphe Mulungu kuti adzetse milumilu yachuma kapena
amutumizire angelo kuti aziyenda naye limodzi. Ndipo adalinso kumaichitira
Qur'an chibwana Mtumiki akawawerengera. Potero Mtumiki (SAW) adali
kubanika mumtima mwake akafuna kufikitsa uthenga kwa iwo chifukwa
chakuopa kutsutsidwa ndi kumchitira chibwana.
Su rat 11. Hud
Juzu 12
459
U *>»
> ^ ^ 5jj-
adachita m'menemo
zidzaonongeka, Ndiponso
nzopanda phindu Zimene
ankachita.
17. Nanga kodi munthu yemwe
ali ndi chisonyezo Choonekera
chochokera kwa Mbuye wake
(Kotero kuti m'moyo mwake
akuyenda molungama; Yemwe ndi
mneneri Muhammad {SAW})
Ndipo Mboni ili naye pamodzi
ikumtsata yochokera Kwa lye
(Mbuye wake yomwe ndi Qur'an
kapena Gaburiel) ndipo patsogolo
pake padali Buku la Musa lomwe
lidali chitsanzo Chabwino ndi
mtendere, (wotereyu angafanane
Ndi yemwe ali mum'dima wa
umbuli yemwenso Sadziwa
cholinga chakulengedwa kwake?)
Awa ndi amene (aongoka)
akulikhulupirira (Buku ili la
Qur'an) ndipo amene ati
Asalikhulupirire m'magulu (a
adani), Moto ndiwo malo awo
alonjezo. Choncho, Usakhale ndi
chipeneko pa ichi; ndithudi Ichi
ndi choona chochokera kwa
Mbuye Wako koma anthu ambiri
sakhulupirira.
18. Ndipo palibe oipa kwambiri
kuposa Yemwe wapeka bodza
pakunamizira Mulungu (kuti ali
ndi mwana ndi Athandizi). Iwo
adzawabweretsa Kwa Mbuye
«$*§&«$&&
®,
' 9* VSi
vy&&
Suratll.Hud
Juzu 12
460 I 1 1 *>»
^ ^ syi Sjj^»
wawo (tsiku la Kiyama) Ndipo
mboni (zomwe ndi angelo)
Zidzanena; "Awa ndi omwe
Adapekera Mbuye wawo bodza.
Mverani! Temberero la Mulungu
Lili pa ochita zoipa kwambiri.
19. Omwe akuletsa anthu
kutsata Njira ya Mulungu ndi
kufuna Kuikhotetsa (njirayo).
Ndiponso iwo sakhulupirira za
Tsiku lomaliza."
20. Iwowa sangathe
kumulepheretsa Mulungu
M'dziko, ndiponso alibe atetezi
Pambuyo pa Mulungu. Chilango
chawo chidzaonjezeredwa
(Chifukwa cha zoipa zawo). Sadali
Kutha kumva ngakhale kuona
(Chifukwa cha mkwiyo umene
udali M'mitima mwawo wokwiira
choonadi).
21. Awa ndi omwe adziononga
okha Ndipo zomwe adali kuzipeka
Zidzawataika.
22. Zoonadi, iwo ndi otaika
Kwakukulu pa tsiku lomaliza.
23. Ndithu, amene akhulupirira
ndi Kumachita zabwino ndi
kumadzichepetsa Kwa Mbuye
wawo, iwowo Ndiwo anthu a ku
Munda wa Mtendere. M'menemo
adzakhala Muyaya.
24. Fanizo la magulu awiriwa
(Asilamu Ndi osakhulupirira), lili
"^^IcPAW^
S 9 9 . V 9 ?
©,
G&$\>%8\&J&&
s&j&e-^
iSS^SSJ^S^lfi
Surat 11. Hud
Juzu 12
461
It *>»
\ \ ijA jj~*
ngati (Munthu) wakhungu ndi
gonthi, ndi (Munthu) wopenya ndi
wakumva. Kodi awiriwa angakhale
ofanana (Pa chikhalidwe chawo)?
Bwanji simukuganiza? 1
25. Ndipo ndithu, Ife tidamtuma
Nuhi (Monga Mtumiki) kwa anthu
ake (Kuti akawauze): "Ine kwa inu
Ndine mchenjezi wofotokoza
(Chilichonse);
26. Ndikuti musapembedze
aliyense Koma Mulungu basi.
Ndithu, Ine ndikukuoperani
chilango cha Tsiku lalikulu
lopweteka (ngati Inu mupembedza
milungu yabodza".)
27. Ndipo pompo akuluakulu
mwa omwe Sadakhulupirire mwa
anthu ake, Adati: "Sitikukuona
koma ndiwe Munthu monga ife,
ndipo sitikukuona koma kuti
akutsata anthu a pansi pathu
ofooka panzeru (Omwe
sadalingalire mozama za iwe).
Ndipo sitikukuonani kuti muli ndi
Ulemerero ndi ubwino wochuluka
Kuposa ife. Koma
tikukuganizirani Motsimikiza kuti
ndinu onama."
28. (lye) adati: "E inu anthu
anga! Kodi muona bwanji ngati
ndili ndi Chisonyezo chowonekera
**""
1 Imam Zamahashariyi adati: "Adawafanizira osakhulupirira ngati akhungu ndi
agonthi, ndipo okhulupirira ngati openya ndi akumva".
Su rati 1. Hud
Juzu 12
462
\y *>i
\ ^ sy* qjj~>
chochokera kwa Mbuye Wanga
ndipo wandipatsa chifundo
chochokera Kwa lye (monga
uneneri), ndipo Nkukhala
chosokonezeka kwa inu, Kodi
tingakukakamizeni kuvomereza
Pomwe simukufuna?"
29. "Ndipo E inu anthu anga!
Ine sindikukupemphani Chuma pa
uthengawu. Palibe Malipiro a ine,
koma ali kwa Mulungu Basi.
Ndipo ine sindingathamangitse
Amene akhulupirira (monga
Momwe mudandipemphera kuti
Ndiwathamangitse anthu ofooka
kuti Inu mulowe m'malo mwawo),
ndithu Iwo adzakumana ndi
Mbuye wawo, ndipo ine
Ndikukuonani monga anthu
osazindikira (mbuli).
30. "Ndipo E inu anthu anga!
Ndani Angandithandize kwa
Mulungu ngati
Nditawathamangitsa? Kodi
simuganiza?
31. "Ndipo ine sindikukuuzani
kuti Ndili ndi nkhokwe zachuma
cha Mulungu kapena kuti ine
Ndikudziwa zinthu zamseri,
ndiponso Sindinena kuti ndine
m'ngelo. Ndiponso sindinena kwa
omwe Maso anu akuwachepetsa
kuti Mulungu sadzawapatsa
chabwino. Mulungu akudziwa
zam'mitima Mwawo. (Ngati
SO rat 11. Hud
Juzu 12
463 * t *jA-i
^ ^ ^^a ^jj* -
nditatero) Ndiye kuti ine
pamenepo Ndili m'gulu la oipa."
32. (Iwo) adati: "E iwe Nuhi!
Watsutsana Nafe, ndipo
wachulukitsa kutsutsana Nafe.
Choncho bweretsa kwa ife
Chimene ukutilonjezacho, ngati
ulidi Mmodzi mwa onena zoona.
33. Adati: "Ndithu, Mulungu
Achibweretsa kwa Inu ngati afuna,
ndipo Inu simungathe
Kumulepheretsa (chimene
wafuna).
34. "Ndipo kulangiza kwanga
Sikungakuthandizeni ngati Ntafuna
kukulangizani ngati Mulungu
akufuna kukulekelerani Kusokera.
lye ndiye Mbuye wanu. Ndipo kwa
lye mudzabwezedwa."
35. Kapena akunena
(osakhulupirira Am'Makka kuti:
"Muhammad) Waipeka (Qur'an
mwa iye yekha)"? Nena ngati
ndayipeka ndiye Kuti machimo
ake (akupekawo) ali pa ine. Ndipo
ine ndili kutali Ndi chiweruzo
chanu cha zoipa Zimene
mukuchita.
36. Ndipo tidamuululira Nuhi
kuti: "(Tsopano) sakhulupirira
aliyense Mwa anthu ako kupatula
okhawo Akhulupirira kale.
Choncho, Usadandaule pazimene
Adali kuchita.
Suratll.Hud
Juzu 12
464
IT tj±\
S \ ^jA 5jj-u
37. Ndipo khoma chombo
moyang'aniridwa Ndi Ife, ndi
ulangizi wathu (satha Kukuchitira
choipa), ndipo usandiyankhulitse
Za iwo amene achita Zoipa (kuti
ndiwakhululukire). Ndithudi, Iwo
amizidwa."
38. Ndipo adayamba kukhoma
chombo. Nthawi iliyonse
akamdutsa akuluakulu a Mwa
anthu ake, adali kumchitira
chipongwe. Naye ankanena (kuti):
"Ngati inu Mukutichitira
chipongwe, nafenso
Tidzakuchitirani chipongwe
monga Momwe mukutichitira
chipongwe."
39. "Posachedwa mudziwa kuti
ndani Chimdzere chilango
chomuyalutsa Ndikumtsikira
chilango chopitirira."
40. Kufikira pamene lidadza
lamulo lathu, madzi Naphulika
muuvuni, (chomwe chidali
Chisonyezo chaNuhi chosonyeza
Kudza kwa lamulo loona kwa
anthu ake) Tidamuuza (kuti):
"Kweza m'menemo (M'chombo)
mtundu uliwonse (wa Nyama),
ziwiriziwiri, (yaikazi Ndi
yaimuna), ndi anthu a Kubanja
lako kupatula omwe Chiweruzo
(cha Mulungu) chatsimikizidwa pa
iwo (kuti aonongeke), Ndipo
(atengenso onse) amene
tia/*-*'
&&P
Suratll. Hud
Juzu 12
465
It *>■!
^ ^ ay* 3jj-»
Akhulupirira." Komatu ndi ochepa
Kwambiri amene adakhulupirira
Pamodzi ndi iye.
41. Ndipo (Nuhi) adati:
"Kwerani M'menemo mwadzina la
Mulungu Mkuyenda kwake ndi
mkuima kwake. Ndithu Mbuye
wanga Ngokhululuka Kwambiri,
Ngwachisoni."
42. Ndipo chombocho chidali
chikuyenda Nawo m'mafunde
onga mapiri, ndipo Nuhi adaitana
mwana wake yemwe adali Patali
(atakana kulowa m'chombo):
"Mwana wanga! Kwera pamodzi
ndi ife Usakhale pamodzi ndi
Osakhulupirira."
43. (Iye) adati: "Ndithawira
kuphiri Likanditeteza kumadziwa."
Nuhi adati: "Lero palibe
otetezedwa ku Lamulo la Mulungu
kupatula Yemwe Mulungu
Wamchitira chifundo." Pompo
mafunde adatchinga pakati pawo.
Choncho adali mgulu la omizidwa.
44. Ndipo (pambuyo
poonongeka onse ndi Zonse
zomwe Mulungu adafuna kuti
Zionongeke), kudanenedwa: "E
iwe nthaka! Meza madzi ako,
"Ndipo iwe Thambo! Amange
(madzi ako amvula)." Choncho,
madzi adaphwa ndipo lamulo
Lidakwaniritsidwa. (Loononga
vyi^i^sgsat
••
®
<»» <9*l'.\'? ' ,4\\' >*>'
1&BU
'JU
®&^»
Suratll.Hud
Juzu 12
466
It pjk-\
\ \ i^ft 5jj-
anthu Oipa). Ndipo (chombo)
chidaima Pamwamba pa (phiri
lotchedwa) Judi, Ndipo
kudanenedwa: "Aonongeke Onse
ochita zoipa."
45. Ndipo Nuhi adafuulira
Mbuye wake Nati. "E Mbuye
wanga! Ndithu, Mwana wanga ali
mgulu la akubanja langa
(Akuonongedwa). Ndipo ndithu,
Lonjezo lanu ndiloona, ndipo Inu
Ndinu Woweruza mwachoonadi
kuposa Aweruzi onse."
46. (Mulungu) adati: "E iwe
Nuhi! Ndithu, iyeyo simwana wa
m'banja Lako. lye zochita zake
Sizili zabwino. Choncho
Usandipemphe zomwe
siukuzidziwa Ine ndikukulangiza
(kuti) usakhale M'gulu la
osazindikira (mbuli)."
47. (Nuhi) adati: "E, Mbuye
wanga! Ndikudziteteza mwa Inu
kuti Ndisakupempheninso zomwe
sindikuzidziwa. Ngati
simundikhululukira Ndi
kundichitira chifundo, Ndikhala
mwa anthu otaika."
48. Kudanenedwa: "E, iwe
Nuhi! Tsika (Pa nthaka youma)
mwamtendere Wochokera kwa Ife,
ndipo madalitso Ambiri akhale pa
iwe ndi Pa anthu omwe ali nawe;
ndipo Kudzakhala mibadwo ina
Su rat 11. Hud
Juzu 12
467
\y *>-i
> > SjJb Sjj-**
(yoipa Pambuyo pako) yomwe
tidzaisangalatsa, Ndipo kenako
chidzaikhudza Chilango chowawa
chochokera Kwa Ife."
49. Izi ndi zina mwa nkhani
zobisika zomwe Tikukuululira iwe.
Siudali kuzidziwa, Iwe ngakhale
anthu ako, patsogolo Pa ichi,
(Qur'an isadadze). Choncho,
pirira. Ndithu, mathero Abwino
adzakhala kwa anthu oopa
Mulungu.
50. Ndipo anthu amtundu wa
Adi, tidawatumizira mbale wawo
Hud. Adati: "E inu anthu anga!
Pembedzani Mulungu! (Siyani
kupembedza Mafano). Mulibe
Mulungu wina Koma lye. Inu
simuli kanthu Koma ndinu opeka
bodza (n'kunena Kwanu kwakuti
mafano ndi anzake A Mulungu)
51. "E inu anthu anga!
Sindikukupemphani Malipiro pa
ichi (uthengawu). Palibe Malipiro
anga koma ali kwaYemwe
Adandilenga. Kodi mulibe nzeru?
52. Ndipo E inu anthu anga!
Pemphani Chikhululuko kwa
Mbuye wanu, (Pamachimo omwe
mwakhala mukuchita), Kenako
lapani kwa lye. Akutumizirani
Mitambo yodzetsa mvula yambiri,
Ndipo akuonjezerani mphamvu pa
Mphamvu zanu (zomwe muli
rrfii i
IUA
Suratll.Hud
Juzu 12
468
>y fr>i
> \ syt ojj^
nazo). Choncho, musatembenuke
kukhala oipa"
53. (Iwo) adati: "E iwe Hud!
Sudatibweretsere Chisonyezo
chooneka (chosonyeza Kuti ndiwe
Mneneri), ndipo ife sitisiya
(Kupembedza) milungu yathu
chifukwa cha Zoyankhula zakozo.
Ndipo ife sitikukhulupirira"
54. "Sitinena kanthu, koma kuti
(mwina) Milungu yathu ina
yakulodza Misala." (lye) adati:
"Ndithu, ine Ndikupereka umboni
kwa Mulungu ndipo inunso
Perekani umboni kuti ine ndili
Kutali ndi zimene mukumphatikiza
nazo (Mulungu pomazipembedza),
55. Kusiya lye; (milungu
yanuyo sindikuiopa Ngati ili ndi
mphamvu pamodzi ndi inu)
Ndichitireni chiwembu Nonsenu,
ndipo kenako
musandiyembekezere
(Musandipatse nthawi).
56. Ndithu, ine ndatsamira kwa
Mulungu, Mbuye wanga ndiponso
Mbuye wanu. Palibe Cholengedwa
chilichonse koma Mulungu
Wachigwira tsumba lake
(ndikuchiyendetsa Mmene
akufunira). Ndithudi, Mbuye
Wanga Ngwachilungamo.
57. Ngati munyoza (kulandira
chimene Ndakuuzani palibe vuto
'^5}%S&£&k*
'Zti'A.i
*'l.'i'A.
^m^<m^^
%
>£*>
)&i&Xl®f&$®
Suratll.Hud
Juzu 12
469
>r *j*-i
> ^ i^ft Ojj--
kwa ine); Ndithu, ndafikitsa kwa
inu Chimene ndatumidwa. Ndipo
Mbuye wanga (awaononga
Osakhulupirira) ndi kubweretsa
Anthu ena m'malo mwanu, ndipo
Inu simungamusautse konse.
Ndithu, Mbuye wanga ndi Msungi
Wa chilichonse.
58. Ndipo pamene lamulo lathu
lidafika (Lakuwaononga),
tidampulumutsa Hud ndi amene
adakhulupirira Pamodzi naye,
mwachifundo Chathu, Ndipo
tidawapulumutsa kuchilango
Chokhwima. 1
59. Ndipo awa ndi Adi.
Adatsutsa Aya za Mbuye wawo
ndi kunyoza Atumiki Ake; ndipo
adatsata Lamulo la yense
wodzikweza, Wamakani.
60. Ndipo adawapachika
matemberero Pa moyo wapano
padziko lapansi Ndi tsiku la
Kiyama (tsiku la Chiweruzo).
Dziwani! Ndithu, Adi adakana
Mbuye wawo. Ha! Adaonongeka
Adi, anthu a Hud!.
61. Ndipo kwa anthu amtundu
wa Samud, (Tidatuma) m'bale
wawo Swaleh. Adati: "E inu anthu
1 Chilangocho chidali chimphepo choononga chomwe chinagumula nyumba
ndi kulowa m'mphuno za adani a Mulungu ndi kutulukira kokhalira kwawo.
Chinkangowagwetsa chafufumimba kotero kuti anthu adali lambilambi ngati
mathunthu a mitengo ya kanjedza.
Suratll.Hud
Juzu 12
470
\y *>l
> ) sy* djf*
anga! Lambirani Mulungu. Mulibe
Mulungu wina koma lye yekha.
lye Adakuumbani ndi nthaka ndi
kukukhazikani M'menemo.Ndipo
mpempheni Chikhululuko (pa
zolakwa zanu), Kenako
tembenukirani kwa lye. Ndithu,
Mbuye wanga ali pafupi (Ndi
akapolo Ake). Ndipo Ngovomera
mapempho (aopempha)".
62. Iwo adati: "E iwe Swaleh!
Ndithudi, udali woyembekezeka
(Kukhala mfumu kwa ife)
patsogolo Pa izi (usanabwere ndi
izi). Ha! Kodi ukutiletsa
kuwalambira omwe makolo Athu
adali kulambira? Ndithu, ife Tili
m'chikaiko chokaikira zomwe
Ukutiitanirazo."
63. (lye) adati: "E inu anthu
anga! Mukuona bwanji ngati ndili
ndi Chisonyezo choonekera
chochokera kwa Mbuye wanga
(chosonyeza kuona kwa
Zimenezi), nandipatsanso chifundo
Chochokera kwa lye. Nanga ndi
Yani angandipulumutse
kuchilango Cha Mulungu ngati
nditamunyoza? Choncho,
simungandionjezere China chake
koma kutaika basi.
64. "Ndipo E inu anthu anga!
Iyi ngamira Ya Mulungu ndi
chisonyezo kwa Inu. Ilekeni izidya
panthaka Ya Mulungu, ndipo
9 \ 6 'V* 9,<9}9 '\''^JJ " *l 1 l
Siiratll.Hud
Juzu 12 471 \ r tjA-i
S \ ijjfc djj^i
musaikhudze Ndi choipa kuopa
kuti chilango Chachangu
chingakuonongeni . " '
65. Koma adaipha. Choncho
(Swaleh) Adati: "Sangalalani
m'midzi Yanuyi pamasiku atatu.
(kenako Mulangidwa). Limenelo
ndi lonjezo Osati labodza."
66. Choncho pamene lamulo
Lathu Lidadza (lakuononga
midziyo), Tidampulumutsa Swaleh
ndi anthu Amene adakhulupirira
naye, Kukuyaluka kwa tsiku
limenelo, Mwa chifundo chathu.
Ndithu, Mbuye wako ndi Mwini
mphamvu, Ngopambana.
67. Ndipo amene adadzichitira
okha Zoipa phokoso lalikulu
lidawaononga, Tero kudawachera
m'nyumba Zawo ali lambilambi
(atafa)
68. Ngati kuti iwo mudalibemo
m'menemo. Mverani! Ndithu,
Asamudu adamkana Mbuye wawo.
Choncho Asamudu Adaonongeka.
69. Ndipo ndithu, atumiki athu
(angelo) Adadza kwa Ibrahim ndi
uthenga Wabwino. (Iwo) adati:
^&$£$£Z'$&Jfc
^j&jt»ti&M>
&P&&tojffij$$&
i) • » u* *h X' 9 \
1 Asamudu adampempha chozizwitsa Mneneri wawo Swaleh chotsimikiza kuti
iye adalidi Mneneri wa Mulungu. Chozizwitsa chomwe adampempha nkuti
atulutse ngamira patanthwe. Choncho mwamphamvu za Mulungu ngamira
idatuluka m'tanthwemo. Ndipo adawauza kuti asaichitire choipa. Aisiye
izingodzidyera m'dziko la Mulungu. Koma iwo adaipha, ndipo chilango cha
Mulungu chidawatsikira.
Su rat 11. Hud
Juzu 12 472 > Y %^r\
\ \ SjJb Qjj**
"Mtendere!" (lye) adayankha
"Mtendere (ukhale pa inu!)" Ndipo
(Ibrahim) sadakhalitse
(Adafulumira) kudza nayo nyama
Yootcha ya thole (mwana wa
ng'ombe)
70. Koma pamene adaona kuti
manja Awo sakuwatambasula
kuchakudya Adawadodoma,
Nadzadzidwa nawo mantha. (Iwo)
Adati: "Usaope; ndithu, ife
Tatumidwa kwa anthu a Luti (kuti
Tikawaononge ndiponso kukupatsa
Nkhani yabwino)."
71. Ndipo (m'menemo nkuti)
Mkazi wake (wa Ibrahim) Ali
chiimire, ndipo adaseka. Kenaka
tidamuuza uthenga wabwino
(Wakubadwa kwa) Isihaka ndipo
Pambuyo pa Isihaka, Yakubu .
72. (lye) adati: "Kalanga ine!
Ndibereka pomwe ine ndili
Nkhalamba, ndiponso uyu
Mwamuna wanga ndi nkhalamba?
Ndithudi, ichi ndi chinthu
Chododometsa."
73. (Angelowo) adati:
"ukudabwa Ndi lamulo la
Mulungu? Chisomo Cha Mulungu
ndi madalitso Ake Zili pa inu, E
inu eni nyumba iyi! lye
Ngoyamikidwa, Mwini ulemelero!"
74. Ndipo pamene Ibrahim
mantha adamchokera
«$W»fc3
4^M?&s&s®$
^^m^&w®*
&
'*te}&y*&<tix$i
Suratll.Hud
Juzu 12
473
>T t,jfr\
> ^ i^A *jj~*
Ndikumufikira uthenga wabwino,
Adayamba kutidandaulira za anthu
a Luti (kuti tisawaononge).
75. Ndithu, Ibrahim adali
wodekha Wodandaulira Mulungu,
wobwerera Kwa lye mwachangu,
76. (Tidamuuza): "E, iwe
Ibrahim! Siya ichi. Lamulo la
Mbuye wako, Ndithu, ladza. Ndipo
ndithu, iwo Chiwadzera chilango
chosabwezedwa.
77. Ndipo atumiki athu pamene
adafika Kwa Luti, iye anadandaula
za iwo Ndi kubanika mumtima
(chifukwa Chosowa njira
yowatetezera kwa Anthu oipa
pomwe iye sadadziwe Kuti
alendowo ndi Angelo), Nati: "Lino
ndi tsiku lovuta".
78. Ndipo anthu ake adadza
akuthamangira Kwa iye (ku
nyumba kwake Kuti adzachite
zauve ndi alendowo). Ndipo
kalenso ankachita zoipa
zokhazokhazi (Luti) adati: "E
anthu Anga! Nawa asungwana
anga; Ngoyenera kwa inu
(kuwakwatira, Osati amuna
anzanu) choncho, Opani Mulungu,
ndipo musandiyalutse Pamaso pa
alendo anga. Kodi mwa inu Mulibe
munthu woongoka?"
79. (Iwo) adati: "Ndithu,
ukudziwa Bwino kuti tilibe
^dSu&^uS&jitf
Suratll.Hud
Juzu 12
474
^r *jk*
\ \ *y* 5 jj~-
khumbo ndi Atsikana ako. Ndipo
ndithu, iwe Ukudziwa bwino
chimene tifuna".
80. (lye) adati: "Ndikadakhala
nayo Mphamvu (yomenyana nanu)
kapena Kotsamira kolimba
kwamphamvu (Ndikadalimbana
nanu kuti musachite Zauve ndi
alendowa)".
81. (Athengawa) adati: "E iwe
Luti! Ife Ndi athenga a Mbuye
wako. Safika kwa Iwe (ndi
chilichonse choipa). Ndipo Choka
pamodzi ndi banja lako m'gawo la
Usiku, ndipo aliyense wa inu
asatembenuke (Kuyang'ana
m'mbuyo akamva mkokomo
Wakudza kwa chilangocho),
kupatula Mkazi wako; iye
chimpeza chimene chiwapeze
Anthu enawo. Ndithu, lonjezo
lawo ndi M'mawa. Kodi m'mawa
suudayandikire?"
82. Choncho, pamene lidadza
lamulo lathu, Tidaugadabula
(m'zindawo) kumwamba Kukhala
pansi, pansi kukhala kumwamba,
Ndipo tidawavumbwitsira mvula
ya Sangalawe zopangika ndi dongo
lotentheka Ndi moto, zogwirana
kwambiri.
83. (Sangalawezo) zokhala ndi
zizindikiro Kwa Mbuye wako.
(sangalawe iliyonse Idali ndi
<s^%^*^ (jrsifcM
V 9 K 9 W \ 9 *
s ' . (V •* *'*«"' * 9 £, ' *
©"rt^j^l
Sural 11. Hud
Juzu 12
475
>Y *>t
^ ^ ^yb 5jj->
mwini wake); ndipo chilango
Chimenechi sichili kutali ndi anthu
Oipa.
84. Ndipo,ku Madiyani
tidamtuma m'bale wawo Shuaibu
iye adati: "E inu anthu anga!
Pembedzani Mulungu; mulibe
Mulungu wina koma Iye. Ndipo
musachepetse mulingo wa mbale
Ndi wasikelo (powapimira anthu)
Ine ndikukuonani kuti ndinu Opeza
bwino, ndipo ndikukuoperani
Chilango cha tsiku lalikulu Lomwe
lidzakuzingani.
85. Ndipo E inu anthu
anga!Kwaniritsani Mulingo
wambale ndi wasikero
Mwachilungamo, ndipo
musawachepetsere Anthu zinthu
zawo (mwachinyengo). Ndipo
musafalitse zoipa padziko ndi
Cholinga chodzetsa chisokonezo.
86. Chuma chimene wakusiirani
Mulungu (m'njira yovomerezeka)
Ndicho chabwino kwa inu ngati
Muli okhulupirira. Ndipo ine
Sindine msungi wanu".
87. Adati: "E iwe Shuaib! Kodi
Mapemphero ako akukulamula
(Kuti utilamule) kuti tisiye Zimene
makolo athu ankapembedza,
kapena kuti tisiye Kuchita zimene
tifuna pachuma Chathu? Ndithudi,
iwe ndiwe Wanzeru, ndi
G^j"^
Suratll.Hud
Juzu 12 476 > Y *j*-i
> > ijA Ojj-*
wolungama." (Izi Adali kumnenera
m wachipong we) .
88. (lye) adati: "E inu anthu
anga! Mukuona bwanji ngati ndili
ndi Chisonyezo chochokera kwa
Mbuye Wanga, ndipo nkundipatsa
riziki Labwino (lahalali) lochokera
Kwa lye, (ndisiye zimenezi ndi
Kusankha njira yokhota)? Ndipo
sindifuna kusiyana nanu Pochita
chimene ndakuletsani. Sindifuna
china, koma kukonza Mmene
ndingathere; ndipo Kupambana
kwanga (pazimenezi) Kuli kwa
Mulungu. Kwa lye Ndatsamira,
ndipo kwa lye Ndikutembenukira.
89. "Ndipo E inu anthu anga!
Kutsutsana Nane
kusakuchimwitseni kuopera Kuti
chingakupezeni chonga chimene
Chidawapeza anthu a Nuhi kapena
Anthu a Hud kapenanso anthu a
Swaleh; ndipo anthu a Luti sali
Kutali ndi inu.
90. "Ndipo mpempheni
chikhululuko Mbuye wanu ndipo
lapani kwa lye (Posiya machimo
ndikuchita zabwino). Ndithu,
Mbuye wanga Ngwachisoni
Ngwachikondi chochuluka (Kwa
anthu ake)."
91. (Iwo) adati: "E, iwe
Shuaib! Sitikumvetsa zambiri
mwazomwe Ukunena. Ndipo ife
Suratll.Hud
Juzu 12 477 I ) t tjJt-i
> > SjA jj~-
tikukuona Wofooka mwa ife.
Pakadapanda Akubanja lako,
tikadakugenda ndi Miyala. Ndipo
ulibe ulemerero Pa ife (koma
tikusunga ulemu wa Anthu
akubanja lako)." 1
92. (lye) adati: "E inu anthu
anga! Kodi anthu akubanja kwanga
ndiwo Olemekezeka kwambiri
kwa inu Kuposa Mulungu? Ndipo
mwamuyika lye (Mulungu)
kukhala kumbuyo Kwa misana
yanu. Ndithu, Mbuye Wanga zonse
zimene mukuchita Akuzidziwa
bwinobwino.
93. "Ndipo E anthu anga!
Chitani (zimene Mufuna) mmene
mungathere; inenso Ndichita
chimodzimodzi (mmene
Ndingathere). Posachedwapa
mudziwa ndani Chimufike
chilango chomsambula, ndipo
Ndani wabodza. Ndipo dikirani
inenso Ndidikira pamodzi ndi inu."
94. Ndipo pamene lamulo lathu
lidadza, Tidampulumutsa Shuaib
pamodzi ndi amene
Adakhulupirira naye,
mwachifundo Chathu. Ndipo
amene adachita Zoipa, phokoso
lidawachotsa moyo, Tero
®^^M^^^^^i
&
&
l >*.*"'<"'
1 Anthu ake ankamuuza izi zoti sakumvetsa zomwe iye anawauza
mwachibwana, nawafanizira malangizo akewo monga malangizo a munthu
wozunguzika nzeru.
Suratll.Hud
Juzu 12
478
^r *>i
\ \ Sj* Ojj-4
kudawachera M'nyumba zawo ali
lambilambi (atafa)
95. Ndiye ngati sadakhalemo,
tamverani! Adaonongeka (anthu) a
ku Madiyani Monga momwe
adaonongekera a Samudu!
96. Ndipo ndithu, tidamtuma
Musa pamodzi ndi Zozizwitsa
zathu ndi maumboni Oonekera.
97. Kwa Farawo ndi nduna
zake. Koma iwo Adatsata lamulo
la Farawo, ndipo Lamulo la
Farawo siloongoka.
98. Tsiku la Kiyama, (Farawo)
Adzawatsogolera anthu ake ndi
Kuwafikitsa ku moto. Ndipo
taonani pamalo poipa kufikirapo.
99. Iwo adatsatizidwa ndi
temberero Pano padziko lapansi
ndipo patsiku La Kiyama
(adzatsatizidwanso) Taonani
kuipa, mphoto (Yawo) yopatsidwa.
100. Izi ndi zina mwa nkhani za
m'mizinda (Zomwe)
tikukusimbira.Ina Mwa iyo
ikadalipobe, ndipo ina Idatha.
101. Ndipo sitidawachitire
choipa (Powaononga). Koma
adadzichitira Okha zoipa
(pakusakhulupirira Mulungu ndi
kupembedza mafano Ndikuipitsa
padziko); milungu Yawo yomwe
ankaipembedza kusiya Mulungu,
°*$ > -W
Suratll.Hud
Juzu 12
479
IT *>i
\ ) SjA djj--
siidawathandize chilichonse
Pamene lidadza lamulo la Mbuye
wako (la kuwaononga). Ndipo
(milunguyo) siidawaonjezere
(China chake) koma chionongeko
Basi.
102. Ndipo mmenemo ndi
momwe kumakhalira Kulanga kwa
Mbuye wako pamene Alanga
anthu a m'mizinda Akakhala oipa
(pamakhalidwe). Ndithu, kulanga
Kwake (Mulungu) Nkowawa,
nkwaukali.
103. Ndithu, m'zimenezi muli
lingaliro Kwa yemwe akuopa
chilango cha Tsiku lomaliza.
Limenelo ndi Tsiku
losonkhanitsidwa anthu. Ndipo
limenelo ndi tsiku Lochitiridwa
umboni (ndi Zolengedwa zonse).
104. Ndipo sitikulichedwetsa
koma m'nthawi Yowerengeka
(kwa Mulungu, ngakhale Kuti kwa
anthu likuoneka kuti lili Kutali.)
105. Tsiku lakudza (zoopsa
zake), Sazalankhula aliyense koma
mwachilolezo Chake (Mulungu).
Ena Adzakhala oipa, ndipo (ena)
Adzakhala abwino.
106. Tsono amene adzakhala
oipa Kobwerera kwawo nkumoto.
Iwo adzakhala m'menemo Akufuula
potulutsa mawu ndi kuwabweza
(Monga kulira kwa bulu).
*&&$m®&
Suratll.Hud
Juzu 12
480 1 1 >>i
> > ayh ojj-u
107. Adzakhala m'menemo
kwa nthawi yonse Yomwe thambo
ndi nthaka zidzakhalire, Kupatula
Mbuye wako akadzafuna. Ndithu,
Mbuye wako Ngochita chimene
wafuna.
108. Tsono amene adzakhale
abwino adzakhala M'munda wa
mtendere. Adzakhala mmenemo
Kwa nthawi yonse yomwe thambo
ndi Nthaka zidzakhalire, kupatula
Mbuye wako Akadzafuna; zopatsa
(za Mbuye wako Ndizo zopatsa)
zosatha.
109. Choncho, usakhale ndi
chipeneko Pazimene awa
akuzipembedza (Zakuti similungu
yoona). Sapembedza koma
momwe Amapembedzera makolo
A wo kale. Ndipo ndithu, Ife
Tiwapatsa gawo lawo (la chilango)
Mokwanira popanda kuchepetsa.
110. Ndipo ndithu, tidampatsa
buku Musa, Koma kusiyana
kudabuka mmenemo
(Pakatanthauzidwe ka bukulo
Pambuyo pa Musa). Pakadapanda
Mawu a Mbuye wako omwe
adatsogola (Oti sadzawalanga
nthawi Isanafike),ndithu
kukadaweruzidwa pakati pawo.
Ndipo ndithu, iwo ali m'kukaika
ndi kupeneka Kwakukulu
pazimenezo.
Suratll.Hud
Juzu 12
481
U *j*-i
> > ^ djj^
111. Ndipo ndithu, Mbuye wako
Adzawapatsa onsewo mphoto
Yazochita zawo mokwanira. Ndithu,
lye Ngodziwa (zonse) Zimene
akuchita.
112. Choncho (E iwe Mtumiki!)
Pitiriza kulungama monga momwe
Akulamulira (iwe) pamodzi Ndi
omwe atembenukira (kwa
Mulungu), ndipo musapyole
Malire. Ndithu, lye akuona Zonse
zimene muchita.
113. Ndipo musapendekere kwa
amene Sali olungama kuopa kuti
Chilango cha moto
chingakukhudzeni; Ndipo
simudzakhala ndi Atetezi kwa
Mulungu, ndipo Potero
simudzathandizidwa(Chilichonse).
114. Ndipo pemphera Swala
mbali ziwiri Za usana ndi nthawi
za usiku Zomwe zili pafupi ndi
usana. Ndithu, zabwino
zimachotsa Zoipa. Ichi ndi
chikumbutso Kwa okumbukira.
115. Ndipo pirira (E! Iwe
Mtumiki! Pokwaniritsa malamulo
a Mbuye Wako)! Ndithu, Mulungu
sataya Malipiro a ochita zabwino.
Iff < *iA'"b' <<i
2*
*2&&
*Gs^%iS*mj&
1 Apa akutanthauza kuti ngati chikhalidwe chamibadwo yakale chidali chonchi,
mibadwo yomwe adaitumizira buku lake, natsutsana ndi bukuli, ena aiwo
nalitaya kutaii, iweyo pitiriza ndi Asilamu omwe uli nawo kugwira njira
yolungama monga momwe Mulungu wakulamulira. Usapyole malire
ponyozera chimene chili choyenera iwe kuchichita, kapena kudzikakamiza
chimene sungathe kuchichita. Mulungutu akudziwa zonse zomwe muchita
ndipo adzakulipirani.
Su rat 11. Hud
Juzu 12
482
\y *jA-i
\ \ SjA *J>^
116. Kodi bwanji sadakhalepo,
Mumibadwo ya anthu akale, Eni
nzeru (omvera Akalangizidwa),
Oletsa kuononga padziko Kupatula
ochepa amene Tidawapulumutsa
Mwa iwo? Ndipo amene
Adadzichitira okha zoipa adatsata
Zomwe adasangalatsidwa nazo,
Choncho, adali oipa.
117. Ndipo Mbuye wako sali
woononga Midzi mopanda
Chilungamo pomwe Eni ake
(midziyo) ali ochita zabwino.
118. Ndipo Mbuye wako
akadafuna, Anthu onse
akadawachita kukhala Mumpingo
umodzi. Choncho saleka Kukhala
osiyana (maganizo), 1
119. Kupatula omwe Mbuye
wako Wawachitira chifundo; ndipo
chifukwa Cha chifundocho,
adawalenga (koma okha
Akusankha zoipa). Ndipo mawu a
Mbuye Wako akwaniritsidwa
(akuti):"Ndithudi, Ndidzadzadzitsa
Jahannama ndi ziwanda ndi
Anthu onse pamodzi (omwe adali
oipa)."
120. Ndipo tikukusimbira zonse
mwa Nkhani za aneneri zomwe
tikukulimbikitsa nazo mtima.
Akadawakakamiza onse kukhala mpingo umodzi. Koma adawapatsa nzeru
ndi mphamvu yozindikirira zinthu kuti asankhe chomwe afuna, chabwino
kapena choipa.
Suratll.Hud
Juzu 12
483
)1 *>i
\ \ $j& &JJ~»»
Ndipo M'zimenezi choonadi
chakufika Ndi ulaliki ndiponso
chikumbutso Kwa okhulupirira.
121. Ndipo auze amene
sadakhulupirire (Kuti); "Chitani
Mmene mungathere; nafenso
tichita (Mmene tingathere)".
122. "Ndipo dikirani
(chiweruzo cha Mulungu) nafenso
tikudikira".
123. Zonse zobisika
zakumwamba ndi Pansi nza
Mulungu ndipo zidzabwezedwa
Kwa lye. Choncho, mpembedzeni
ndi Kutsamira kwa lye. Ndithu,
Mbuye wako siwonyalanyaza
zimene Mukuchita.
Surat 12. Yusuf
Juzu 12
484
IT *>i
^ T «-i—»jj *jj— »
Sura ya Yusuf ndi imodzi mwa Sura zomwe
zidavumbulutsidwa ku Makka ndipo ikunenetsa za nkhani ya
mneneri wa Mulungu, Yusuf mwana wa Yakubu, ndi masautso
osiyanasiyana amene adakumana nawo ochokera kwa abale ake
omwe ankamchitira njiru. Ikufotokozanso za masautso omwe
adakumana nawo m'nyumba ya Aziz wa ku Misir ndipo kenako
nkukalowa m'ndende.
Cholinga cha nkhaniyi ndikutonthoza mtima wa mtumiki
Muhammad (SAW) kumasautso omwe amapezana nawo
kuchokera kwa anthu ake.
Surat 12. Yusuf Juzu 12 485 \ 1 *>i
\ y UU>y *jj-j
Surat Yusuf XII
Life:*"
^ ^^^^ai^ < <t--.^ u-ii
M'dzina la Mulungu waChifundo
Chambiri, waChisoni.
1. Alif-Lam~Ra. Izi ndi aya za
m'buku Lomwe likuonetsera
poyera (chilichonse Chofunika).
2. Ndithu, Ife taivumbulutsa
Qur'an Ya Charabu kuti inu
Muzindikire.
3. Ife tikukusimbira nkhani
zabwino Pokuzindikiritsa Qur'an
iyi; ndithu, Udali mmodzi mwa
osadziwa zinthu, Isanakufike.
4. Akumbutse za Yusuf pamene
adauza tate Wake: "E inu tate
wanga! Ndithu, Ine ndaona kutulo
nyenyezi khumi ndi Imodzi, dzuwa
ndi mwezi, zonsezo Ndaziona
zikundigwadira".
5. (Tate wake) adati: "E iwe
mwana wanga! Usawasimbire
abale ako maloto ako Kuopa kuti
angakuchitire chiwembu; Ndithu,
Satana kwa munthu, ndi mdani
Woonekera. !
6. Ndipo momwemo Mbuye
wako Akusankha komanso
akuphunzitsa Kumasulira
nkhani(zamaloto) ndi
qWllfc^JMt,
©
1 Sibwino munthu kufotokozera anthu chisomo chako chonse ngati palibe
zofunikira kutero. Dziwani kuti mwini madalitso ngochitiridwa dumbo.
Surat 12. Yusuf
Juzu 12
486
>r frjA-i
> T ei~»»jJ *JJ-"
Kukwaniritsa mtendere Wake pa
iwe, ndi Pambumba ya Yakubu
monga momwe Adakwaniritsira
kwa makolo ako kale, Ibrahim ndi
Isihaka. Ndithu, Mbuye Wako
Ngodziwa, Ngwanzeru zakuya."
7, Ndithu mwa Yusuf ndi
abale Ake, muli malingaliro ambiri
kwa ofunsa (Zinthu kuti adziwe).
8, Kumbuka pamene (abale a
Yusuf) adati: "Ndithu, Yusuf ndi
m'bale wake (Benjamini)
ngokondedwa kwa bambo Wathu
kuposa ife pomwe ife ndife gulu
Lamphamvu. Ndithu, bambo
wathu ali Mkusokera koonekera
(sadziwa yemwe Ali ndi
chithandizo chokwanira)."
9. Mupheni Yusuf kapena
mukamponye kudziko (Lakutali),
kuti nkhope ya Bambo wanu
Ikutembenukireni (pakuti nthawi
Imeneyo Yusuf sadzakhalapo,
yemwe Akumkonda kwambiriyo);
Ndipo pambuyo Pake (mutalapa
tchimoli) mdzakhala Abwino,
(kwa Mulungu)." 1
10. Adanena wonena mwa iwo:
"Musamuphe Yusuf, koma
mponyeni m'chitsime chakuya;
'
1 Dyera loipa kwambin ndiko kunena koti: "Tandislyani ndichite machimo,
kenako ndidzalapa." Dziwani kuti machimo omwe Mulungu angawakhululukire
ngomwe munthu wawachita mosazindikira kapena kuti popanda kuwafunafuna,
osati owachita mwadaladala ncholinga choti adzalapa pambuyo pake monga
momwe abale ake a Yusuf ankaganizira.
Surat 12. Yusuf
Juzu 12
487 I i y *>■>
> Y <*J)-*tjt 6jj~*
Adzamtola ena apaulendo ngati inu
Mwalingadi kutelo."
11. (Pambuyo pogwirizana
paganizo lomuponya M'chitsime
chakuya adapita kwa Bambo Wawo)
anati: "E Bambo wathu! Kodi
Bwanji simutikhulupirira pa Yusuf,
Pomwe ife timamfunira zabwino?
12. Mperekeni mawa pamodzi
ndi ife (Kubusa) kuti akadye
mokondwa ndi Kusewera;
ndithudi, ife tikamsamala."
13. (Bambo wawo) adati:
"Ndithu, Zikundidandaulitsa
Zakuti mupite naye; Ndikuopa kuti
Angajiwe ndi mimbulu pomwe inu
Simukulabadira za iye."
14. (Iwo) adati: "Ngati mimbulu
itamudya Pomwe ife ndife gulu
lanyonga kwambiri, Ndiye kuti
tidzakhala otaika.
15. Ndipo pamene adanka naye
ndi Kugwirizana pakati pawo kuti
amuike Mchitsime chakuya,
(adamuikadi) .Ndipo
Tidamzindikiritsa iye (Yusuf):
"Ndithu udzawauza chinthu
chawochi (Chimene akuchitirachi)
pomwe iwo sakudziwa."
16. Ndipo adadza kwa Bambo
wawo madzulo Akulira,
17. Akunena: "E Bambo
wathu! Tidapita Kokapikisana
-~H$UPti?&
^&p&ft$R$&
Surat 12. Yusuf
Juzu 12
488 I > t *>■'
) Y UJ~*»JJ *JJ—*
(kuthamanga), ndipo Tidamsiya
Yusuf pomwe padali ziwiya Zathu;
choncho mimbulu yamudya Koma
inu simutikhulupirira (pazimene
Tikukuuzanizi) ngakhale kuti
Tikunena zoona."
18. Ndiponso adabwera ndi
mkanjo wake (wa Yusuf )uli ndi
magazi abodza. (Bambo wawo
pamene Adauona mkanjo wo uli
wosang'ambika) Adati: "Koma
mitima yanu yakukometserani
Chinthu (chomwe mwamchitira
mnzanu Mwa chifuniro chanu;
ndipo chimene ine Ndingachite
ndi) kupirira kwabwino; ndipo
Mulungu ndi Wopemphedwa
chithandizo Pazimene
mukunenazi.
19. Ndipo aulendo adadza
(pafupi ndi chitsimecho) Ndipo
adatuma wotunga madzi wawo,
Choncho iye adaponya ndowa
yake (Mchitsime, ndipo akukoka
ndowa ija Adaona mwana) nati:
"Eee, chisangalalo Changa! Aka
kamwana kakamuna! Pomwepo
Iwo (amene adalipo pachitsimepo)
Adambisa kwa apaulendo anzawo)
monga Katundu wamalonda
(yemwe adamgula). Koma
Mulungu ankadziwa zimene adali
Kuchita (ndipo adanka naye ku
Iguputo). 1
19-20. Apa tikuona kuti kugulitsana anthu kudayambika kalekale zedi
Surat 12. Yusuf
Juzu 12
489
^r tjA-i
^ Y ci~*»jj ^J-**
20. Ndipo adamgulitsa
pamtengo wochepa Ndi ndalama
zapang'ono, zowerengeka (Poopa
kuti angawadzere eni Mwanayo).
Ndipo sadalabadire za iye.
21. Ndipo uja (amene)
adamgula ku Iguputo, Adati kwa
mkazi wake: "Mkonzere pokhala
Pabwino (kapolo uyu): mwina
angatithandize Kapena
tingamsandutse kukhala mwana
(wathu)." Motero tidamkhazika
Yusuf m'dziko (La Iguputo
mwachisangalalo), ndi kuti
Timphunzitse kumasulira nkhani
(zamaloto). Ndipo Mulungu
Ngopambana pa zinthu Zake
(zimene Wafuna kuti zichitike);
koma anthu Ambiri sadziwa.
22. Ndipo pamene (Yusuf)
adafika pa msinkhu, Wodzindikira
zinthu tidampatsa kuweruza ndi
Nzeru. Umo ndi momwe
timawalipirira ochita Zabwino.
23. Ndipo mkazi uja yemwe
m'nyumba mwake Mudali iye
adamlakalaka (Yusuf) Popanda iye
kufuna. Ndipo (mkaziyo) Adatseka
makomo, nati: "Bwera kuno."
(Yusuf) adati: "Ndikudzitchinjiriza
©,
&»»
(il^l
't^t^*^i^3vaU
*&w)2m
kuyambira zaka 4,000 zapitazo chipembedzo cha Chisilamu chisanadze,
chomwe chidaza ndi Mtumiki Muhammad(SAW). Koma adani achipembedzo
cha Chisilamu akuchinamizira kuti ndicho chidadza ndi ukapolo wogulitsa
anthu. Chikhalirecho Chisilamu ndicho chidadza kuzalimbikitsa zopereka ufulu
kwa kapolo.
Surat 12. Yusuf
Juzu 12
490
>t ftjfcl
\ t <Ji-*»jj ^J-**
Ndi Mulungu (kuchita tchimolo).
Ndithu iye (Mwamuna wako) ndi
bwana wanga. Wandikonzera
bwino pokhala panga (M'nyumba
mwakemu, ndipo sindichita
Chinyengo chotere). Ndithu,
achinyengo Siziwayendera bwino."
24. Ndipo (mkaziyo) adaikira
mtima pa iye (Kuti achite naye
kanthu) ndipo naye (Yusuf)
adaikira mtima pa iye (kuti
Ammenye). Pakadapanda kuona
chisonyezo Cha Mbuye wake
(chakumzindikiritsa kuti Asatero,
akadammenya. Koma adamthawa).
Tidachita izi kuti timchotsere
chinthu Choipa ndi chauve;
ndithudi, iye adali Mmodzi mwa
akapolo athu oyeretsedwa. *
25. Ndipo (onse awiri)
adathamangitsana Kukhomo (uku
Yusuf akuthawa) ndipo (Mkaziyo)
adang'amba mkanjo wake
Chakumbuyo. Ndipo mwamuna
wake Adampezerera pakhomo;
mkaziyo adati (Kwa mwamuna
wake mwaugogodi): "Palibe
> <.. ' ' * ?' '. f\ '
(r^l C> loo I {£***&}
1 Musamchitire choipa amene wakuchitirani chabwino, ngakhalenso amene
wakuchitrani choipa kumene. Makamaka amene sadakuchitireni choipa (ndiye
chisimu). Koma alipo anthu ena oipitsitsa zedi amene amachitira zoipa yemwe
akuwachitira zabwino. Anthu otero ngoipitsitsa kuposa nyama zamtchire,
ndipo oterewa Mulungu adzawakhaulitsa koopsa. Ndipo machitidwe okhala
mwamuna ndi mkazi kuseri kwaokha ngoletsedwa M'shariya ya chisilamu
chifukwa mwamuna kukhala ndi mkazi amene sali mnyazi wake
kumalakwitsa. Msati awa ndi alamu ndikhoza kukhala nawo pawokha.
Kukhala ndi mlamu wako kuseri, ndi ngozi imeneyo!
Surat 12. Yusuf
Juzu 12
491
U *>i
1 Y ci-*»jj Sjj—'
Mphoto kwa yemwe akufuna
kuchita Choipa ndi mkazi wako
koma kumponya Kundende,
kapena kupatsidwa chilango
Chowawa."
26. (Yusuf) adati (podziteteza):
"(Mkazi) Uyu ndi yemwe
wandifuna popanda ine
Kumufuna." Ndipo mboni
yochokera ku Banja la mkaziyo
idaikira umboni; (Idati): "Ngati
mkanjo wake wang'ambidwa Cha
kutsogolo,ndiye kuti( mkazi uyu)
akunena zoona, Ndipo iye (Yusuf)
ndi Mmodzi mwa onena zabodza.
27. Koma ngati mkanjo wake
wang'ambidwa Chakumbuyo
ndiye kuti (mkazi uyu) wanena
Bodza ndipo iye (Yusuf) ndi
m'modzi mwa onena Zoona.
28. Choncho (mwamuna uja)
pamene adaona Mkanjo wake (wa
Yusuf) utang'ambidwa
Chakumbuyo, (adadziwa kuti
Yusuf ndi Amene amafuna
kugwirilidwa), Adati: "Ndithudi,
izi ndi ndale zanu akazi. Ndithu,
ndale zanu ndi zazikulu (Iwe
mkazi wanga ndi amene
udatsimikiza Kuchita choipa ndi
m'nyamatayu)."
29. "Yusuf! Zipewe izi
(usauze aliyense). Ndipo (iwe
mkazi) Pempha chikhululuko ku
Oo OJs^^ (itfO^ <*>&$ {^XfiJh
Surat 12. Yusuf
Juzu 12
492
>T frjA-i
^ T UL*ijj 5jj-»»
tchimo lako, Ndithu, iwe ndiwe
mmodzi mwa olakwa!"
30. Ndipo akazi a mu
mzindamo (ataimva Nkhaniyi)
anati: "Mkazi wa nduna
Akulakalaka m'nyamata wake
popanda Kulakalakidwa ndi iye;
ndithu, Chikondi chamufooketsa
zedi; ndithudi, Ife tikumuona
(mkaziyu kuti) ali Mkusokera
koonekera."
31. Ndipo (mkazi wa nduna)
pamene adamva Kunyogodola
kwawo, adawaitana (kuti Adzaone
kukongola kwa Yusuf kuti adziwe
Kuti wathedwa nzeru polakalaka
Yusuf Ngosayenera
kudzudzulidwa). Ndipo
Adawakonzera phwando
ndikupatsa Aliyense wa iwo
mpeni; kenaka adamuuza (Yusuf):
"Tuluka ndi kubwera pamaso Pa
iwo." Choncho pamene (akazi aja)
Adamuona, adaona kuti nchinthu
chachikulu zedi ndipo adadzicheka
manja awo (Ndi mipeni ija.
Sadazindikire kuti Akudzicheka
chifukwa cha chidwi ndi
Kukongola kwa Yusuf), Ndipo
adati, "Hasha Lillah!
(tikudzitchinjiriza kwa Mulungu)
uyu simunthu, uyu Sichina koma
ndi mngelo wolemekezeka."
32. (Mkazi wa nduna) adati:
"Uyu ndi amene
m&fitej$ti*&
Surat 12. Yusuf
Juzu 12
493
>y %}kr\
\ y Ulsjj djj-«»
Mumandidzudzula naye. Ndithudi
ndidamulakalaka pomwe iye
samandifuna ndipo Anadziteteza.
Ndipo ngati sachita Chimene
ndikumulamula, ndithu
Amangidwa ndipo ndithu, akhala
m'gulu La onyozeka!"
33. (Yusuf) adati: "E Mbuye
wanga! Ndende ndi yabwino kwa
ine Kuposa izi akundiitanira. Ngati
simundichotsera ndale Zawo ndiye
kuti Ndiwacheukira ndikukhala
Mmodzi mwa mbuli." 1
34. Ndipo Mbuye wake
Adamuyankha (pempho Lake)
ndikumchotsera ndale zawo.
Ndithudi, Iye Ngwakumva,
Ngodziwa.
35. Kenako kudaoneka kwa
iwo, (nduna ndi Anthu ake)
pambuyo poona zizindikiro (Zonse
zakuyeretsedwa kwa Yusuf) kuti
Akamponye kundende kwa Nthawi
yochepa (pofuna kumusungira
Ulemu mkazi wa nduna).
36. Ndipo anyamata awiri
adalowa m'ndende Pamodzi ndi
iye. M'modzi mwa iwo adati
(Kumuuza Yusuf): "Ndithu, ine
ndalota Ndikufulula mowa." Ndipo
'^l&S&pf ™'*
1 Akazi aja atamuona Yusuf tsiku limenelo nawonso anadzazidwa ndi chikondi
chachikulu nayamba kumtumizira mithenga ndi makalata. Ndipo Yusuf
adaganiza kuti ndibwino angopita kundende poopa kuti akaziwo
angamulakwitse.
Surat 12. Yusuf
Juzu 12
494
^T *>i
^ t *-A-*»jj *j>^
wina adati: "Ndithu ine ndalota
ndikusenza mikate Pamutu panga
yomwe idali kudyedwa ndi
Mbalame." "Tiuze tanthauzo lake.
Ndithu, ife tikukuona iwe kuti
ndiwe Mmodzi wa anthu abwino".
37. (Yusuf) adati: "(Kupyolera
mu uneneri Umene ndapatsidwa
ndingathe kukumasulirani Maloto
anuwa ndi zinthu zina Zobisika
kwa inu), sichikudzerani Chakudya
cha mtundu uliwonse choti
Mungapatsidwe koma ndikhala
Nditakumasulirani tanthauzo lake
chisanakufikeni; (Ngati
mukufunadi ndikuchitirani
zimenezi). Izi ndi zina mwa
zomwe Mbuye wanga
Wandiphunzitsa. Ndithudi, ine
ndasiya Njira za anthu
osakhulupirira Mulungu Ndiponso
omwe akukana za tsiku la
Chimaliziro."
38. "Ndipo ine ndatsata
chipembedzo cha makolo anga
Ibrahim, Isihaka ndi Yakubu;
ndipo Sikudali koyenera kwa ife
kumphatikiza Mulungu ndi
chilichonse. (Ndipo Kuzindikira)
zimenezi ndi ubwino Wa Mulungu
umene uli paife ndi anthu ena.
Koma anthu ambiri sathokoza."
39. "E inu anzanga awiri
am'ndende! Kodi milungu
Yambiri yosiyana ndiyo yabwino
e ^<y^ft)£&
% ^ W»«J WoV- V»5*S5
Surat 12. Yusuf
Juzu 12
495
U 9,£r\
\ y Ul*ijj ^jj-j
(Kupembedzedwa), kapena
Mulungu mmodzi Mwini
mphamvu (pachilichonse)?"
40. "Simupembedza china
kusiya lye (Mulungu) Koma ndi
maina basi amene inu nokha
Mudawatcha ndi makolo anu,
Mulungu Sadatsitse umboni
uliwonse Pazimenezo. Palibe
lamulo lina koma Ndi la Mulungu
basi. Walamula kuti
Musampembedze aliyense koma
lye basi. Chimenecho ndicho
chipembedzo choongoka, Koma
anthu ambiri sadziwa (monga inu
Mulili popembedza mafano)."
41. E inu anzanga awiri
am'ndende! Tsono Mmodzi wainu
(abwerera kuntchito yake)
Azikamwetsa mowa bwana wake
(monga Zidalili poyamba);koma
winayo Aphedwa mopachikidwa,
ndipo mbalame Zidzadya mutu
wake. Chiweruzo chaweruzidwa
Kale (kwa Farawo) pa chinthu
Chomwe mudali kufunsa."
42. Ndipo (Yusuf) adauza
yemwe adamdziwa kuti
Apulumuka mwa awiri wo:
"Ukandikumbuke Ponditchula
pamaso pa Mbuye wako (Farawo;
Ukamuuze kuti ndamangidwa
popanda tchimo)." Koma Satana
adamuiwalitsa kumkumbutsa
Mbuye wake. Tero (mneneri
Siirat 12. Yusuf
Juzu 12
496
\r f-jir\
} Y *-A-*»jJ OjJ-*'
Yusuf) adakhala M'ndende zaka
zingapo.
43. Ndipo (tsiku Una) mfumu
(Farawo adalota) Nati (kwa nduna
zake): "Ndithudi, ine Ndalota
ng'ombe zisanu ndi ziwiri
Zonenepa zikudyedwa ndi
ng'ombe zisanu Ndi ziwiri
zowonda ndiponso ndalota Ngala
zisanu ndi ziwiri zaziwisi ndi zina
(Zisanu ndi ziwiri ) zouma. E inu
Akuluakulu! Ndimasulireni maloto
Angawa, ngati inu mumatha
kumasulira maloto."
44. (Iwo) adati: "Amenewa ndi
maloto Osakanikirana (simaloto
omveka)! Ndipo Ife sitili odziwa
kumasulira maloto Amtundu
umenewu."
45. Pamenepo amene
adapulumuka mwa awiri Aja
adanena atakumbukira (pempho la
Yusuf) patapita nyengo (yaitali),
Adati: "Ine ndikuuzani tanthauzo
Lake. Choncho nditumeni (kuti
ndikakufunireni tanthauzo lake)."
46. (Adanka kundende
ndikumpempha Yusuf
Chikhululuko chifukwa cha
kuiwala kwake. Ndipo adati):
"Yusuf! E iwe woona! Tiuze za
ng'ombe zisanu ndi ziwiri
Zonenepa zikudyedwa ndi zisanu
ndi Ziwiri zoonda, ndi ngala zisanu
taw®*
•'
f- »L* "
1£"
Surat 12. Yusuf
Juzu 12
497
\y *>i
s y ci-^ji &jy
ndi Ziwiri zaziwisi ndi zina
zouma; kuti Ine ndibwerere kwa
anthu kuti akadziwe."
47. (Yusuf) adati: "Mudzalima
zaka zisanu Ndi ziwiri
mondondozana ndi mwakhama
Ndipo zimene mwakolola Zisiyeni
m'ngala zake, kupatula zochepa
Zimene muzidzadya (kuti
zam'ngalazo Mudzadye mzaka
zanjala).
48. "Kenako pambuyo pake
Zidzadza zaka Zisanu ndi ziwiri za
Masautso zomwe zidzadya Zimene
mudasunga m'mbuyo Kupatula
zochepa zimene muzidzazisunga
(Mobisa kuti zidzakhale mbewu.)
49. "Kenako pambuyo pa izi
chidzadza chaka Chomwe anthu
m'menemo adzapulumutsidwa
(Ndi Mulungu). Ndipo m'menemo
adzafinya (Zakumwa)."
50. Ndipo mfumu idati :
"M'bweretseni lye kwa ine."
Koma pamene mthenga (wa
Mfumu) adamfika (Yusuf, iye)
adati: "Bwerera kwa Mbuye wako
ndipo Ukamfunse nkhani ya akazi
omwe Ankadzicheka manja awo.
Ndithu, Mbuye wanga akudziwa
bwino ndale Zawo. (Koma
ndikufuna mfumu kuti Idziwe za
kuyera kwanga kuti Andiyeretsere
maganizo ndipo asandiope)."
%ys®&$&%tiSQ
'''"*&&
Surat 12. Yusuf
Juzu 13
498
>r *jk\
\ V U1~»»JJ *J>^
51. (Mfumu idasonkhanitsa
akazi aja ndipo) idati: "Kodi
nkhani yanu njotani pamene
Mudamulakalaka Yusuf Pomwe
iye asakufuna?" Adati: "Hasha
Lillah! (tikudzitchinjiriza kwa
Mulungu) Ife sitidadziwe choipa
chilichonse kwa iye. (Tidayesayesa
kuti achite nafe Choipa koma
sadalole)." (Nayenso) mkazi wa
nduna adati: "Tsopano choonadi
chatsimikizika; ine Ndine amene
ndidamulakalaka iye Asakufuna.
Ndithu, iye ndi mmodzi mwa Oona."
52. (Yusuf adati): "Zimenezo
(zofuna kuti Afunsidwe chonchi)
n'chifukwa chakuti (Nduna)
idziwe kuti ine sindidaichitire
Zoipa iyo kulibe, ndikuti Mulungu
saongolera ndale za anthu
Achinyengo (kuti ipambane).
53. "Ndipo ine sindikuyeretsa
mtima wanga. Ndithu, mtima
uliwonse umalamulira kwambiri
Ku zoipa kupatula umene Mbuye
wanga wauchitira chifundo.
Ndithudi, Mbuye Wanga
Ngokhululuka, Ngwachisoni.
54. Choncho Mfumu idati:
"Mubwere naye kwa ine kuti ine
Mwini ndimsankhe." Ndipo
pamene adalankhula naye (mfumu)
Idati: "Ndithu, iwe lero kwa ife
Wakhala wolemekezeka,
Wokhulupirika"
Surat 12. Yusuf
Juzu 13
499 hr,j*-i
\ t UL*>ji $jj-»
55. (Yusuf) adati: "Ndiikeni
kukhala Muyang'aniri wankhokwe
zazinthu Zam'dziko lonse.
Ndithudi, ine ndine Msungi
wodziwa."
56. Ndipo motero tidampatsa
ulemerero Yusuf M'dziko (la
Iguputo); amakhala M'menemo
paliponse pamene wafuna.
Timam'bweretsera chifundo
Chathu Amene tamfuna, ndipo
sitisokoneza Malipiro a ochita
zabwino.
57. Ndithudi malipiro a tsiku la
chimaliziro Ngabwino zedi kwa
amene akhulupirira Ndi
kumamuopa (Mulungu).
58. Ndipo adadza abale ake a
Yusuf (kukafuna Chakudya
kumeneko pamene ku Middle East
kudagwa chilala chadzaoneni) Ndi
kulowa kwa iye ndipo (iye)
Adawazindikira pomwe iwo
sankamzindikira.
59. Ndipo pamene
adawakonzera chakudya chawo,
Adati: ("Ngati mudzabwereranso
kachiwiri) Mudzabwere ndi m'bale
wanu wa kumbali Ya bambo anu,
kodi simuona kuti ine
Ndikukwaniritsa muyeso, ndipo
ndine Wabwino kwambiri
polandira (alendo)?"
S&®J&ffiftS&&
®:
9>\'
Sir
@ a^^i
Surat 12. Yusuf
Juzu 13
500
>r tjJ-i
^ y c-a-jjj ^j^*'
60. "Komangati
simudzandibweretsera iye,
Simudzakhala ndi mulingo
(Wachakudya) kwa ine, ndipo
Musadzandiyandikire."
61. (I wo) adati: "Tikayetsetsa
kuwanyengerera Bambo wake za
iye (kufikira Akatipatse). Ndithu,
ife tikachita Zimenezi."
62. Ndipo (Yusuf) adati kwa
anyamata ake a ntchito: "Ikani
chuma chawo m'mitolo Yawo kuti
akachizindikire akabwerera Ku
mawanja awo. (Tinkachita izi)
Mwina angabwererenso (kuno)."
63. Ndipo pamene adabwerera
kwa bambo wawo, Adati: "E
Bambo wathu ! Tikamanidwa
Muyeso wachakudya (paulendo
wachiwiri Pokhapokha titsagane
ndi m'bale wathuyu). Choncho
mtumizeni m'bale wathu pamodzi
Ndi ife kuti akatipimire (mlingo
Wokwana); ndithu, ife
tikamsunga."
64. (Yakubu) adati: "Kodi
ndingakukhulupirireni Pa iye
kuposa momwe
Ndidakukhulupirirani pa m'bale
wake Kale (yemwe
mudamsokeretsa)? Koma Mulungu
ndi Yemwe ali wabwino posunga,
Ndipo Iye Ngwachifundo kuposa
Achifundo onse.
Surat 12. Yusuf
Juzu 13
501
\T *>1
^ T ci-*»jj ^jj- -
65. Ndipo pamene adatsekula
katundu wawo, Adapeza chuma
chawo chabwezedwa kwa Iwo.
Adati: "E, Bambo wathu!
Tingafunenso chiyani (kwa
munthu Waufuluyu)? Ichi chuma
chathu Chabwezedwa kwa ife;
ndipo tikabweretsa chakudya
chothandizira mawanja athu;
Ndipo m'bale wathu tikamsunga;
Tikapezanso muyeso wangamira
imodzi Yoonjezera. Umenewu ndi
mlingo Wochepa(kwa mfumu ya
ufuluyo).
66. (Yakubu) adati:
"Sindingamtumize Pamodzi ndi
inu pokhapokha mundipatse
Lonjezo m'dzina la Mulungu kuti
ndithudi Mudzambweza kwa ine
pokhapokha Nonsenu
mutazingidwa (ndi zoopsa). Ndipo
pamene adapereka lonjezo lawo,
(lye) adati: "Mulung ndiye
Muyang'aniri (mboni) pazimene
tikunenazi."
67. Adatinso: "E inu Ana anga!
Musakalowe (mu Iguputo)
Pachipata chimodzi koma
kaloweni Pazipata zosiyanasiyana.
Ndipo Sindingakuthandizeni
chilichonse Kwa Mulungu.
Lamulo ndi la Mulungu Basi; kwa
lye ndiko ndatsamira; ndipo
Otsamira atsamire kwa lye."
yi
®6%J$\$j&&j
Surat 12. Yiisuf
Juzu 13
502
>r *>i
\ T <-i-»ji ^J***
68. Ndipo pamene adalowa
monga momwe Bambo Wawo
adawalamulira, sikudawathandize
Chilichonse kwa Mulungu
kupatula Khumbo lomwe lidali
mumtima mwa Yakubu
(Ndi lomwe) adalikwaniritsa
(Yakubu Adali kufuna Yusuf ndi
m'bale Wake akumane mwamseri;
ndipo Adakumanadi). Ndithu iye
(Yakubu) Adali wanzeru chifukwa
chakuti Tidamphunzitsa. Koma
anthu ambiri Sadziwa.
69. Ndipo pamene adalowa kwa
Yusuf (Ndikumuona m'bale wake
atalowa Payekha), adamkumbatira
m'bale wakeyo Nati: "Ndithu, ine
ndine m'bale Wako; choncho
usadandaule pazimene (Abale
athu) akhala akuchita."
70. Ndipo pamene
adawakonzera chakudya Chawo,
adaika chikho chomwera madzi
Mumtolo wa m'bale wakeyo.
Kenako Woitana adaitana: "E inu
apaulendo! Inu ndinu anthu akuba.
71. (Onse abale ake a Yusuf)
pamene Adawacheukira, adati:
"Kodi Mukusowa chiyani?"
72. Adati: "Tikusowa muyeso
wa Mfumu; Ndipo amene
aubweretse, alandira Mtolo
wangamira yathunthu; (ndipo
Mneneri Yusuf adati): "Ndipo ine
Ndine muimiriri pa zimenezi."
Surat 12. Yusuf
Juzu 13
503
ir *>i
) T ci-^JJ 6jJ**>
73. (Iwo) adati: "Tikulumbirira
pali Mulungu! Ndithu, inu
mukudziwa Kuti sitidadze
kudzaononga mdziko, Ndiponso
sitili akuba."
74. Adati: "Mphoto (chilango)
yake Ikhala yotani ngati Mukunena
bodza?"
75. Adati: "Mphoto yake ndi
yemwe (Chikhocho) chapezeka
mumtolo wake, lye ndiye mphoto
yake. (Agwidwe Monga kapolo
kwa chaka chimodzi)". Umu ndi
momwe timawalipirira anthu
Achinyengo.
76. Ndipo (mneneri Yusuf)
adayamba Kufufuza m'mitolo
mwawo asanafufuze Mumtolo wa
m'bale wake; kenako
Adachitulutsa mumtolo wa m'bale
wake. Umu ndi momwe
tidamlinganizira ndale Yusuf (kuti
ampeze m'bale wake).
Mwachilamulo cha mfumu (ya
m'dzikolo) Sakadamutenga m'bale
wake (monga kapolo) Koma
mmene Mulungu adafunira
(powaonetsaAbale ake za
chilamulo cha kwawo chomuika
Mu ukapolo munthu wakuba).
Timawakwezera Paulemerero
amene tawafuna.Ndipo pa
wodziwa Aliyense pali
wodziwanso kuposa iye.
Siirat 12. Yusuf
Juzu 13
504
>T frjA-i
\ Y <-i-»ji *j>"'
77. (I wo) adati: "Ngati waba,
m'bale Wakenso adabapo kale."
(Uku kudali Kumunamizira Yusuf
bodza pomwe iwo Sankadziwa
kuti yemwe akuyankhula Nayeyo
ndiye Yusuf). Koma Yusuf
Adabisa (mawu awa) mumtima
mwake, (Chifukwa chowamvera
chisoni) ndipo Sadawaululire.
Adati: "Inu muli ndi Chikhalidwe
choipa ndipo Mulungu akudziwa
Zomwe mukunena!"
78. (Iwo) adati: "E inu bwana!
Uyu ali ndi Bambo wake
wokalamba Kwambiri; choncho
Tengani mmodzi wa ife mmalo
mwake; Ndithudi, ife tikuona kuti
inu ndinu Mmodzi mwa ochita
zabwino".
79. (Yusuf) adati: "Ha!
tikudzitchinjiriza Mwa Mulungu,
sitingagwire wina koma Yemwe
chuma chathu tachipeza ndi iye,
Kuopa kuti tingakhale ochita zoipa.
80. Choncho, pamene adataya
mtima za iye, Adapita pambali
kukanong'onezana. Wamkulu
wawo adati: "Kodi simudziwa Kuti
Bambo wanu adatenga lonjezo
Kuchokera kwa inu m'dzina la
Mulungu (Kuti mudzambweza
iyeyo?) Ndiponso Kale mudalakwa
(pamapangano anu) pa Za Yusuf.
Choncho sindichoka dziko Lino
kufikira atandilola Bambo
Surat 12. Yusuf
Juzu 13
505 ir*j*-i
^ t <-A-«»ji ^jj- -
(kutero) kapena Mulungu
andilamule (zondichotsa kuno
Pomasulidwa m'bale wangayu);
lye Ngwabwino Polamula kuposa
olamula.
81. "Bwererani kwa abambo
anu ndipo mukawauze (Kuti): "E
Bambo wathu! Ndithu mwana
wanu Adaba. Ndipo ife sitidaikire
umboni (Wakuti wakuba
achitidwe ukapolo) Koma
pazomwe tidazidziwa (kuti mwaife
Mulibe wakuba), ndipo sitidali
Kudziwa zamseri."
82. "Ndipo afunseni anthu A
m'mudzi mom we Tidalimo ndi
apaulendo Omwe tadza
nawo,ndipo Ndithudi ife tikunena
zoona."
83. (Yakubu) adati: "Koma
mitima yanu Yakukometserani
chinthu. (Kwa ine Ndi) kupirira
kwabwino kokha basi. Mwina
Mulungu adzandibweretsera Onse
pamodzi. Ndithudi, lye Ngodziwa,
Ngwanzeru zakuya."
84. Ndipo adawachokera
ndikunena (Kuti): "Ha!
kudandaula kwanga za Yusuf!"
Ndipo maso ake adayera Chifukwa
cha kudandaula ndipo iye
Adadzadzidwa ndi chisoni.
85. (Iwo) adati: "Pali Mulungu!
Simusiya kumkumbukira Yusuf
Surat 12. Yusuf
Juzu 13
506
>r sjA-i
^ T *-A-»*Ji *JJ-*'
(Ndikulira) mpaka mufika
podwala, Kapena mukhale mwa
owonongeka (ndi Imfa)."
86. (lye) adati: "Ndithu, ine
ndikusuma Dandaulo langa ndi
kukhumata kwanga Kwa Mulungu,
ndipo ndikudziwa Kupyolera mwa
Mulungu zomwe Simukudziwa."
87. "E ana anga! Pitani
mukafufuzefufuze Za Yusuf ndi
mbale wake, ndipo Musataye
mtima pa chifundo cha Mulungu.
Ndithu, palibe amene amataya
Mtima za chifundo cha Mulungu
koma Anthu osakhulupirira."
88. (Ndipo adapita ku Iguputo).
Choncho Pamene adalowa kwa iye
(Yusuf) adati: "E inu
olemekezeka! Masautso
Atikhudza, ife ndi maanja athu;
Choncho tabwera ndi chuma
chopanda Pake. Tidzadzireni
mlingo (ngakhale Chuma
chathucho chili chopanda pake),
Ndipo tichitireni zaufulu. Ndithu
Mulungu Amalipira ochita
zaufulu."
89. (Iye) adati: "Kodi
mukudziwa zomwe Mudamchitira
Yusuf ndi m'bale wake Pamene
inu mudali mu umbuli?"
90. (Iwo) adati: "Kodi iwe
ndi we Yusuf?" Adati: "Ine ndine
Yusuf, ndipo uyu Ndi m'bale
Surat 12. Yusuf Juzu 13 I 507 I > r *>»
\ t U^**jt ^jj**
wanga; Mulungu watichitira
Zabwino. Ndithu, amene aopa
Mulungu Ndikumapirira,
(Mulungu amulipira). Ndithu,
Mulungu sasokoneza malipiro
Aochita zabwino."
91. (Iwo) adati: "Pali Mulungu!
Mulungu Wakusankha pa ife,
ndipo ife tidalidi Olakwa."
92. (lye) adati: "Lero palibe
kukudzudzulani; Mulungu
akukhulukirani, Ndipo lye
Ngwachifundo chochuluka Kuposa
achifundo."
93. "Pitani ndi mkanjo wangawu
ndipo Mukauponye pamaso pa
Bambo wanga Ndipo iwo akapenya.
Kenako nonsenu Ndi mawanja anu
onse mudze kwa ine."
94. Ndipo aulendo pamene
adamuka (Kubwerera kwawo).
Bambo wawo (Yemwe adali ku
Sham) adati: "Ndikumva fungo la
Yusuf pakadapanda Kuti muli ndi
chikhulupiriro choti
Ndasokonezeka nzeru,
(mukadandikhulupirira.")
95. (Iwo) adati: "Pali Mulungu!
Ndithu Muli mkusokera kwanu kwa
kale (Pokonda Yusuf kuposa ife)."
96. Choncho pamene adadza
wotenga nkhani Yabwino,
adauponya (mkanjo wa Yusuf)
Surat 12. Yiisuf
Juzu 13
508
IT frj*-i
^ T ei— »jj ^jj-*'
Patsogolo pankhope yake, ndipo
Pompo adapenya. Adati: "Kodi
Sindinakuuzeni kuti ine
ndikudziwa Kupyolera mwa
Mulungu zomwe inu
Simukuzidziwa?"
97. (Iwo) adati, "E Bambo
wathu! Tipemphereni chikhululuko
pa Machimo athu. Ndithu ife
tidali Olakwa."
98. (lye) adati: "Posachedwapa
(ndikamuona Yusuf)
ndikupempherani chikhululuko
Kwa Mbuye wanga. Ndithu, lye
NgokhululukaZedi, Ngwachisoni."
99. Ndipo pamene adalowa
Kwa Yusuf, adawakumbatira
Makolo ake ndikunena: "Lowani
mu Iguputo, Insha'llah, (Mulungu
akalola) Mwamtendere."
100. Ndipo (pamene adafika
kwa Yusuf),(Iye) adawakweza
Makolo ake ndi kuwaika
pampando (wake) wachifumu,
Ndipo onse adagwa kumlambira
(monga Mwachizolowezi chawo
nthawi imeneyo). Ndipo (Yusuf)
Adati: "E inu Bambo wanga! Hi
ndilo tanthauzo (lenileni) La
maloto anga akale. Palibe
chipeneko Mbuye wanga
Wawatsimikiza (maloto wo). Ndipo
adandichitira Zabwino
ponditulutsa kundende ndi
®6J^<Mt6^1
Surat 12. Yusuf
Juzu 13
509
\T *j*-l
^ t *-i~»»jj *j>- , >
pokubweretsani Inu kuchokera
kuchipululu, pambuyo
pokhwirizira (Chidani) Satana
pakati pa ine ndi abale anga.
Ndithudi Mbuye wanga amadziwa
kwambiri chinsinsi cha zomwe
Wakonza kuti zichitike. Ndithu,
lye Ngodziwa, Ngwanzeru.
101. (Kenako adathokoza ndi
kupempha Mulungu kuti): "E
Mbuye wanga! Ndithu,
Mwandipatsako ufumu ndi
kundiphunzitsako Kumasulira
nkhani (zamaloto). E, inu Mlengi
wa thambo ndi nthaka. Inu ndiye
Mtetezi wanga padziko Lapansi
ndi tsiku la chimaliziro. (Ndipo
Nthawi ya imfa yanga)
mudzandipatse imfa Ndili
Msilamu ndipo kandikumanitseni
ndi Ochita zabwino."
102. Izi ndi zina mwankhani
zamseri (Zomwe) tikukuululira
iwe. Ndipo siudali nawo pamodzi
Pamene adatsimika chochita
Chawo (uku) akuchita chiwembu
(Chawo) choipa.
103. Ndipo ambiri mwa Anthu
sakhulupirira Ngakhale utalimbika
chotani.
104. Ndipo sukuwapempha
malipiro Pazimenezi. Sichina izi
(zimene Wadza nazo),koma ndi
ulaliki kwa Zolengedwa zonse.
Surat 12. Yiisuf
Juzu 13
510
\T t>i
^ t <*jL»»ji *jj-^
u*3^]3dP(^fe
/T}> ^ 9 A 9?Y*' 99 'X'9**' S 9) 'J'
mjMS&v&z
j&.
%&$
105. Ndipo ndi zisonyezo
zingati (zosonyeza Kuti Mulungu
alipo) kumwamba ndipansi
Zomwe akuzidutsa pamene iwo
sakuzilabadira. 1
106. Ndipo ambiri a iwo
Sakhulupirira Mulungu Koma
momphatikiza! 2
107. Kodi akudziika pachitetezo
kuti Silingawadzere tsoka
lachilango Cha Mulungu, kapena
kuti siingawadzere Kiyama
mwadzidzidzi pomwe Iwo
sakuzindikira?
108. Nena: "Iyi ndi njira yanga.
Ndikuitanira Kwa Mulungu
mwanzeru zokwanira,ine ndi Omwe
akunditsata. Ndithu, Mulungu
Wapatukana (ndi mbiri zopunguka).
Ndipo ine sindili mwa ophatikiza
(Mulungu ndi zinthu zina)." 3
1 Apa tanthauzo lake nkuti zilipo zisonyezo zambiri zosonyeza kuti Mulungu
alipo zomwe iwo akuziona ali pamudzi ndiponso akuzidutsa akakhala
pamaulendo awo monga thambo, nthaka, dzuwa, mwezi, nyenyezi, mapiri ndi
zina zambiri zododometsa zimene zikupezeka kumwamba ndi pansi.
Akuziona m'mawa ndi madzulo koma iwo saziganizira.
2 Apa akutanthauza kuti ambiri a iwo amamphatikiza Mulungu ndi milungu
yabodza. Iwo amavomereza kuti Mulungu ndiye Mlengi wopatsa zonse. Koma
kuonjezera pachikhulupiriro choterechi, amapembedzanso mafano. Ndipo
zoterezi masiku ano zikumachitika ndi Asilamu ena amene amafuulira mizimu
ya anthu akufa kuti iwathangate pamavuto amene awagwera, komwe
nkumuphatikiza Mulungu ndi mizimu ya anthu akufa.
3 Apa Mtumiki (SAW) akuuzidwa kuti awauze anthu kuti iye pamodzi ndi
amene akumutsata kuti amalalikira Chisilamu kwa anthu popereka kwa anthuwo
mitsutso yanzeru, ndikuperekanso zisonyezo ndi maumboni amphamvu.
Sibwino Msilamu kutsatira chinthu popanda kuchidziwa bwinobwino. Qur'an
ikunenetsa kuti osatsatira chinthu popanda kuchidziwa bwinobwino
pokhapokha chinthucho chitanenedwa ndi Mulungu pena Mtumiki Wake.
i < • ?jx. , . ^ wit, 9 \c 9 k \<"\
Siirat 12. Yusuf
Juzu 13
511
ST *jA-1
^ t Ul*>jj *_)j~*
109. Ndipo sitidatume
(Mtumiki aliyense) Patsogolo pako
koma adali amunaamene
Tidawavumbulutsira
(chivumbulutso); ochokera mwa
Anthu am'midzi. Kodi sadayende
(iwo Osakhulupirira) pa dziko
nkuona momwe Mathero a oipa
omwe adalipo patsogolo Pawo
(momwe adalili)? Ndipo nyumba
ya Tsiku la chimaliziro njabwino
kwa oopa Mulungu. Kodi mulibe
nzeru?
110. Mpaka pamene atumiki
adataya mtima (za Anthu awo)
nkuganiza kuti Ayesedwa
onama,chithandizo chathu
Chidawadzera, ndipo amene
tidawafuna Adapulumuka. Koma
chilango chathu Sichibwezedwa
kwa anthu Oipa.
111. Ndithu, m'nkhani zawo
Izi muli phunziro kwa eni nzeru.
Simawu Opekedwa, koma ndi
chitsimikizo cha zomwe Zidalipo
patsogolo pake (m'mabuku ena a
Mulungu), ndi kumasulira kwa
Tsatanetsatane pa chilichonse
ndiponso chiongoko Ndi mtendere
kwa anthu okhulupirira.
Osatsatira chinthu kaamba koti anthu ambiri akuchitsatira kapena kaamba koti
akuluakulu kapena atsogoleri akuchitsatira. Koma poyamba fufuza kuona
kwake kwa chinthucho. Ndipo ukapeza kuti nchoona, chitsatire.
Muziganizira mwa nzeru zanu zonse pachinthu chilichonse chimene
mukuuzidwa. Kutero ndiko kutsatira zophunzitsa za Qur'an.
Surat 13. Ar-Ra'd Juzu 13
512
)T *jir\
\ T JLP^I 5jj-
SURAT AR-R'AD XIII
Sura iyi yayamba ndi nkhani yaikulu yomwe ndi
kukhulupirira kuti Mulungu alipo. Koma ngakhale zisonyezo
zolangiza kuti Chauta alipo zikuonekera poyera, Amshirikina
akukana. Akuikana Qur'an ndi kumkana Mulungu Mwini
chifundo chambiri.
Ay a za m'Sura iyi zikutsimikizira za kukwanira kwa
mphamvu za Mulungu ndi kudodometsa kwa zolengedwa zake,
monga thambo ndi nthaka, dzuwa ndi mwezi, zomera ndi
zipatso, ndi zonse zomwe Mulungu adalenga padziko lino
lophanuka. Ndipo aya za Surayi, zatsimikiziranso za kuuka ku
imfa ndikuti aliyense adzalipidwa molingana ndi zochita zake.
Ndipo ayazo zikupitiriza kutsimikizira kuti udindo wakulenga,
kupereka moyo, imfa, zabwino, mtendere ndi wa Mulungu.
Kenako Surayi yaponya mafanizo awiri: fanizo la choonadi ndi
fanizo la chonama pofanizira madzi amene amatsika kumwamba
ndikuyenda m'zigwa ndi m'makwalala uku atatenga zinyalala
m'njira mwake. Ndipo thovu limayandama pamwamba pake,
lomwe lilibe phindu. Ndipo madziwo amatsalira ndi kulowa
pansi, omwe anthu amathandizidwa nawo. Umo ndi momwe
chilili choonadi ndi chachabe. Choonadi chimakhazikika ndi
kupitirira pomwe chachabe sichikhalira kutha ngakhale
chitakhala ndi mphamvu zotani.
Kenako aya m' Surayi zafotokoza mbiri za anthu omwe
adzakhale pamtendere, ndi anthu omwe adzakhale pamasautso.
Surat 13. Ar-Ra'd Juzu 13
513
1f(>i
^ T opjJi 5jj~.
Surat Ar-Ra'd XIII
\'SMCM. *
:*
M'dzina la Mulungu waChifundo
Chambiri, waChisoni.
1. Alif-Ldm-Mim-Rd. Izi ndi ay a
za buku ili (lomwe Lasonkhanitsa
chilichonse Chofunika); ndipo
chomwe chavumbulutsidwa Kwa
iwe kuchokera kwa Mbuye wako,
Nchoonadi; koma anthu ambiri
Sakhulupirira.
2. Mulungu ndi Yemwe
adatukula thambo popanda Mizati
imene mukuiona; kenako
adakhazikika Pampando Wake
wachifumu, (Kukhazikika
koyenera ndi lye komwe kulibe
Chofanizira); ndipo adafewetsa
dzuwa ndi Mwezi (kwa anthu).
Chilichonse mwa Zimenezi
chikupitirira kuyenda mpaka
Nyengo imene idaikidwa. lye ndi
Yemwe Akuyendetsa zinthu;
akulongosola aya izi Kuti mukhale
ndi chitsimikizo pazakukumana
Ndi Mbuye wanu. 1
3. Ndipo lye ndiYemwe
adatambasula nthaka Ndikuika
Q&#lfe*ijll^
%PSS
\S9* Si S"
u®^g»A'
1 Mulungu adafewetsa dzuwa ndi mwezi kuti zitumikire anthu Ake. Chilichonse
mwa izo chikuyenda molingana ndi chikonzero cha Mulungu kufikira pamene
lidzathera dziko lapansi. Mulungu ndi Yemwe akuyendetsa zinthu zonse
zapadziko ndi nzeru Zake zakuya, monga kuzipatsa moyo ndi kuzipatsa imfa
ndi zina zotere.
Mulungu akutifotokozera zonsezi kuti tikhale ndi chitsimikizo choti tidzakumana
Naye pambuyo pa imfa.
Surat 13. Ar-Ra'd Juzu 13 514 I ^ r *>i
^ r jlp^Ji 6jj--
mapiri ndi mitsinje m'menemo.
Ndipo mtundu uliwonse wazipatso
Adaupanga m'menemo kukhala
mitundu Iwiri iwiri, (yachimuna
ndi yachikazi), Amavindikira usiku
ndi usana. Ndithu, m'zimenezi
muli zisonyezo (zazikulu
Zosonyeza kuti Mulungu alipo)
kwa Anthu olingalira.
4. Ndipo m'nthaka muli zigawo
zogundana, (Koma kumeretsa
kwake kwa zomera
Nkosiyanasiyana). Mulinso minda
Ya mphesa ndi mmera wina ndi
kanjedza Wokhala ndi nthambi ndi
wopanda nthambi; (Zonsezi)
zikuthiriridwa ndi madzi amodzi
Ofanana, ndipo tikuzichita zina
kukhala Zabwino kuposa zina
mkakomedwe kake. Ndithu,
m'zimenezi muli zisonyezo kwa
anthu Anzeru.
5. Ndipo ngati ukudabwa,(basi)
chodabwitsa Kwambiri ndiko
kuyankhula kwawo (koti): "Kodi
tikadzakhala dothi, ndi zoona
Tidzakhala ndi chilengedwe
chatsopano? (Mulungu sangathe
zimenezi)". Iwowo Ndi amene
sadakhulupirire Mbuye wawo.
Ndipo kwa iwowo mudzakhala
magoli M'makosi mwawo; ndipo
iwo ndi anthu Akumoto,
m'menemo adzakhala muyaya. 1
Mulungu akuti chodabwitsa zedi kwa anthu osakhulupirira ndiko kunena
Siirat 13. Ar-Ra'd Juzu 13
515 h?*>l \Td*J\ Ijy*
6. Ndipo akukufulumizitsa kuti
ubweretse choipa (Chomwe ndi
chilango chawo) m'malo Mwa
chabwino; ndithu chikhalirecho
zilango Zambiri zidapita kale
(zomwe Akadayenera kuchenjera
nazo)! Koma Mbuye wako ndi
mwini chikhululuko kwa Anthu
pa uchimo wawo. Ndipo ndithu
Mbuye wako Ngolanga mwaukali. 1
7. Ndipo osakhulupirira
akunena: "Bwanji Sichidatsitsidwe
kwa iye chozizwitsa Chochokera
kwa Mbuye wake?" Ndithu, Iwe
ndi we mchenjezi, ndipo mtundu
uliwonse Wa anthu uli ndi
muongoli (wakewake yemwe Ali
ndi njira zakezake zoongolera
anthuwo, Osati kutsata njira za
muongoli wina).
8. Mulungu akudziwa
chilichonse chimene Mkazi asenza
(m'mimba mwake) ndi zimene
Mimba zikupungula ndi zimene
zikuonjezera. Chinthu chilichonse
kwa Iye chili ndi Mlingo (wake).
®&0
9*2*
kwawo kwakuti: "Kodi tikadzafa ndi kusanduka fumbi, tidzapatsidwanso moyo
wina watsopano, zidzatheka bwanji zimenezi?" Ndithudi, kukana kwawo za
kuuka kwa akufa nkododometsa pakuti amene adatha kulenga zinthu
zikuluzikulu, monga thambo ndi nthaka, mitengo ndi zipatso, nyanja ndi
mitsinje, ngokhoza kuwabweza pambuyo paimfa yawo.
1 China chodabwitsa cha anthu osakhulupirira mwa Mulungu ndiko kupempha
chilango kuti chiwadzere m'malo mopempha zabwino. Iwo ankanena monga
momwe zilili m'ndime ya 32 m'Surat Anfal kuti: "Ngati izi zimene wadza nazo
Muhammad (SAW)nzoona zochokera kwa inu (Mulungu), choncho timenyeni ndi
chimvula chamiyala yochokera kumitambo; kapena chilango china chilichonse
chopweteka. Koma ife sitimutsatirabe." Umo ndi momwe idalimbira mitima ya
osakhulupirira.
Surat 13. Ar-Ra'd Juzu 13
516 hr^>i
y r op^i oj^
9. (lye ndi Yemwe ali)
Wodziwa zamseri Ndi
zoonekera,Wamkulu,
Wapamwambamwamba.
10. Ndi chimodzimodzi (kwa
lye Mulungu) Amene akubisa liwu
lake mwa inu ndi Amene
akulikweza ndi yemwe akudzibisa
Usiku ndi yemwe akuyenda usana,
(onse Akuwadziwa).
11. (Munthu aliyense) ali nalo
gulu (la Angelo) Patsogolo pake
ndi pambuyo pake (omwe)
Amamulondera (ndi kulemba
zomwe akuchita) Mwa lamulo la
Mulungu. Ndithudi, Mulungu
Sasintha zomwe zilipo kwa anthu
mpaka Atasintha iwo zomwe zili
m'mitima yawo. Ndipo Mulungu
akawafunira anthu chilango, Palibe
chochitsekereza; ndipo alibe
Mtetezi m'malo mwake
(Mulungu) 1
12. lye ndi Yemwe
amakuonetsani kung'anima
Mokuopyezani (kuphedwa ndi
mphezi) Ndi mokupatsani
chiyembekezo chabwino
(Chakudza mvula). Ndipo
®j^%$\?^\jd&\&
Ukaona anthu zinthu zawo sizikuwayendera bwino, dziwa kuti iwo eni ake
asintha chikhalidwe chawo chabwino chomwe adali nacho chomwe
chimawadzetsera madalitso. Munthu akasintha kusiya makhalidwe ake
abwino, zinthu zake zonse zimaonongeka. Munthu amatchedwa munthu
akakhala ndi makhalidwe abwino. Koma akaononga makhalidwe ake abwino
ulemu wake wonse umaonongeka.
Siirat 13. Ar-Ra'd Juzu 13
517
>r fr>»
\ r op^i ojj-
amabweretsa Mitambo yolemera
(ndi madzi amvula).
13. Ndipo mphezi imalemekeza
Mulungu Ndi kumthokoza, naonso
Angelo (Amamlemekeza)
momuopa. Ndipo Mulungu,
Amatumiza kumenya kwa mphezi
ndi Kummenya nako amene
wamfuna. Ndipo Iwo (Akafiri)
akutsutsana pa za Mulungu (Kuti
alipo kapena kulibe pomwe lye
Alipo). Ndipo lye Ngolanga
mwaukali.
14. Kwa lye ndiko kuli
(kuvomera) pempho Lachoonadi.
Ndipo aja amene akupempha
mafano Kusiya lye (Mulungu),
Sawayankha pachilichonse koma
(Chikhalidwe chawo) chili ngati
yemwe Akutambasulira madzi
manja ake awiri Kuti afike
m'kamwa mwake; koma
sangafike. Ndipo mapemphero a
osakhulupirira sali Kanthu koma
ndi otaika basi (opita pachabe).
15. Ndipo amene ali
kumwamba ndi pansi
Amamgwadira Mulungu
Mwachifuniro ndi mopanda
chifuniro; Ndiponso zithunzi Zawo
(zimamgwadira) M'mawa ndi
madzulo.
16. Nena: "Ndani Mbuye wa
thambo ndi Nthaka?" Nena: "Ndi
Mulungu". Nena:
9 '9? 9S S9 *<t\'±»'\\l'" (<
®<p>
'%'
Surat 13. Ar-Ra'd Juzu 13
518
>r *>i
\ r ^pjJi 5jj--
"Mukudzipangira milungu ina
kusiya lye, (Milungu) yomwe
siingadzibweretsere Zabwino
kapena kudzichotsera sautso?"
Nena: "Kodi angakhale ofanana
wakhungu Ndi wopenya? Kodi
kapena ungafanane Mdima ndi
kuunika?" Kapena ampangira
Anzake Mulungu omwe adalenga
zofanana Ndi zomwe Mulungu
adalenga kotero kuti Zolengedwa
(zambali ziwirizo) zikufanana Kwa
iwo? Nena: "Mulungu ndiye
Mlengi wa Chilichonse. Ndipo lye
ndi Mmodzi Wayekha,
Wopambana (ndipo chimene lye
wafuna Ndi chimene
chimachitika")
17. Adatsitsa madzi, kuchokera
kumitambo, ndipo Zigwa
zidayendetsa madzi mwa mlingo
wake. Ndipo msefukiro
wamadzi,udatenga thovu Lomwe
limayandama pamwamba pamadzi.
Ndiponso zomwe amazisungunula
Pamoto chifukwa chofuna
zodzikongoletsera Nazo kapena
ziwiya (monga zagolide ndi
Siliva), mukhalanso thovu
chimodzimodzi. Umo ndi mom we
Mulungu akuperekera Fanizo
lachoonadi ndi fanizo lachonama.
Tsono thovu, limangopita monga
zitakataka Chabe; koma zimene
zimathandiza anthu,
Surat 13. Ar-Ra'd Juzu 13
519
\T %$r\
> T JLP^il «jj-»
Zimakhazikika m'nthaka. Umo ndi
m'mene Mulungu akuperekera
Mafanizo. 1
18. Amene adavomera Mbuye
wawo, adzapeza Zabwino. Koma
amene sadamuvomere, ngakhale
Akadakhala nazo zonse zam'dziko
ndi zina Zonga izo pamodzi,
ndikuzipereka kuti Adziombolere
(sizikadavomerezedwa). Ndipo
Iwo adzakhala ndi chiwerengero
choipa. Ndipo malo awo ndi ku
Jahannama, (Amenewo) ndi malo
oipakwabasi!
19. Kodi amene akudziwa kuti
Zimene zavumbulutsidwa Kwa
iwe kuchokera kwa Mbuye wako
nzoona, Angafanane ndi yemwe ali
wakhungu? Ndithudi eni nzeru ndi
okhawo olingalira;
20. (Iwowo ndi) omwe
akukwaniritsa lonjezo La
Mulungu, ndipo saswa lonjezo
lomangika (Pakati pawo ndi
anzawo);
21. Ndiponso omwe
akulumikiza zomwe Mulungu
Walamula kuti zilumikizidwe
(monga chibale) Pamodzi ndi
kuopa Mbuye wawo ndi kuopanso
1 Nthawi zambiri zinthu zachabe zimagundika kwambiri, koma sizikhalira
kuzimilira. Choncho.nkofunika kwa anthu kuchenjera ndi zinthu zotere.
Asazikhulupirire chifukwa choona kuti zagundika, koma azipenyetsetse bwino,
mofatsa kuti kuona kwake kwa zinthu kutsimikizike kwa iye.
Surat 13. Ar-Ra'd Juzu 13
520
)T *>i
^ t j&J\ 3jj-*»
Chiwerengero choipa (chomwe
chidzawapeza Oipa tsiku
lachimaliziro tero amayesetsa
Kuwapatuka machitidwe oipa);
22. Ndi omwenso amapirira
Chifukwa chofuna chiyanjo cha
Mbuye wawo Ndi kupemphera
Swala ndi kupereka zomwe
Tawapatsa, mobisa ndi moonekera,
Ndi kuchotsa choipa ndi chabwino
(Pochita chabwino pachoipacho);
iwo Ndi omwe adzapeza malipiro
(abwino) a kunyumba Ya tsiku la
chimaliziro. 1
23. Minda yamuyaya adzailowa
Iwo (pamodzi) ndi amene adachita
Zabwino mwa makolo awo, Akazi
awo ndi ana awo; ndipo angelo
Azikalowa kwa iwo khomo lililonse.
24. (Uku akunena) "Salaamu
Alayikamu (Mtendere Uli painu)
chifukwa chakupirira kwanu
(Pochita zabwino ndi kusiya zoipa
ndi kukhala Mwaubwino ndi
anzanu)! Taona kukhala bwino
Zotsatira za nyumba ya tsiku la
chimaliziro."
Kunena kotj "Kupereka mobisa ndi moonekera", kukusonyeza kuti sadaka
zomwe munthu akupereka asazifunire nthawi yake yeniyeni yoperekera.
Koma nthawi iliyonse. Ngati nkofunika kupereka mobisa kuopera kuti omwe
akupatsidwawo asanyozeke kumaso kwa anthu, apereke mobisa. Ndipo ngati
nkofunika kupereka moonetsera, ncholinga choti anthu ena atsanzire, monga
kusonkhetsa kwa poyera apereke moonekera. Tsono kunena kwakuti "kuchotsa
choipa ndi chabwino," kukutanthauza kuti anthu amenewa akawachitira zoipa
ena, iwo sabwezera zoipazo. Koma amapitiriza kuchitira anthu oipawo zabwino.
Surat 13. Ar-Ra'd Juzu 13 I 521 I > r *>»
> T Js-J\ bjj--
25. Koma amene akuswa
lonjezo la Mulungu (Ndi
malonjezo a anthu anzawo)
pambuyo Polimanga motsimikiza,
ndi kumadula Chimene Mulungu
walamula kuti Chilumikizidwe, ndi
kumaononga padziko, Iwowo
ndi wo adzapeza Temberero;
ndiponso adzapeza nyumba yoipa.
26. Mulungu amamtambasulira
riziki amene Wamfuna, ndipo
amamfumbatiranso
(Kumchepetsera amene wamfuna).
Ndipo Akusangalalira moyo
wapadziko lapansi, Suli kanthu
moyo wapadziko poyerekeza Ndi
moyo wa Pambuyo pa imfa, koma
ndi Chisangalalo chochepa basi.
27. Ndipo amene
sadakhulupirire akunena: "Bwanji
Sizidatsitsidwe kwa iye zozizwitsa
kuchokera Kwa Mbuye wake?"
Nena: "Ndithu, Mulungu
amalekerera kusokera amene
Wamfuna (chifukwa chosafuna
kutembenukira Kwa Iye
Mulungu); ndipo amamuongolera
Amene akutembenukira kwa Iye."
28. "(Awa ndi) amene
akhulupirira, ndipo Mitima yawo
ikukhazikika pokumbukira
Mulungu. Dziwani, pokumbukira
Mulungu mitima imakhazikika
(Imatonthola)"
Kit "k ."ii ^i \~*a*<> ' w
Siirat 13. Ar-Ra'd Juzu 13
522 hr*j*-i
\ T J*J\ Ojj-*»
29. "Amene akhulupilira Ndi
kumachita Zabwino, chisangalalo
Nchawo ndi Mabwerero abwino."
30. Momwemo takutuma kwa
anthu omwe adapita Patsogolo
pawo anthu ena (ndipo amva
Nkhani zawo zonse); kuti
uwawerengere Zimene
tikukuvumbulutsira; koma iwo
Akumkana (Mulungu) Wachifundo
chambiri. Nena: "Iyeyo ndi Mbuye
wanga! Palibe Wopembedzedwa
mwachoonadi koma lye;
Ndatsamira kwa lye, ndipo
kobwerera kwanga Nkwa lye basi."
31. Ndipo ikadakhalapo Qur'an
yomwe chifukwa Chaiyo mapiri
akadayendetsedwa (panthawi
Yoiwerenga), kapena chifukwa cha
iyo, Nthaka ikadang'ambidwa,
kapena chifukwa Cha iyo, akufa
akadalankhulitsidwa,(yochititsa
Zimenezi ikadakhala Qur'an iyi.
Koma ntchito ya Qur'an
siimeneyo)! Zinthu zonse nza
Mulungu. Kodi sadadziwebe
amene Akhulupirira, kuti Mulungu
akadafuna Akadawaongolera anthu
onse (ku chisilamu; Akadawalenga
monga Angelo opanda zilakolako
Koma wawapatsa nzeru ndi
zilakolako kuti Alimbane ndi
ziwiri; ena apambane Ndikulowa
kumunda wamtendere). Ndipo
Tsoka silisiya kuwapeza amene
Surat 13. Ar-Ra'd Juzu 13 523 > ? *>»
> T J*J\ ijf
sadakhulupirire Chifukwa cha
zomwe achita, kapena Litsika
pafupi ndi dziko lawo kufikira
Lonjezo la Mulungu lifike
(lowachotsa Moyo), ndithudi,
Mulungu saswa malonjezo (Ake).
32. Ndipo ndithu adachitidwa
chipongwe Aneneri Akale iwe
usanadze koma ndidawalekerera
amene Sadakhulupirire
(sindidawalange mwachangu),
Ndipo kenako ndidawathira
dzanja. Kodi Chilango changa
chidali chotani!
33. Kodi amene akuimirira
mzimu uliwonse Pazimene
udapeza (kuti adzaulipire, Sindiye
woyenera kupembedzedwa)?
Ndipo Ampangira Mulungu
anzake . Nena: "Atchuleni
(Anzakewo)." Kodi kapena
mukumuuza Zomwe sakuzidziwa
pa dziko, kapena ndi Mawu chabe
(opanda cholinga chilichonse
Zomwe mukunenazo)? Koma
amene sadakhulupirire
akometsedwa ndi bodza lawoli
Lamkunkhuniza, ndipo
atsekerezedwa kunjira
(Yachoonadi). Ndipo amene
Mulungu wamulekerera Kusokera
alibe muongoli (wina
Wakumuongolera).
34. Ali nacho chilango m'moyo
wadziko lapansi, Koma chilango
&&^ij$d&&%
Siirat 13. Ar-Ra'd Juzu 13
524
>r tj±\
\ r j*J\ 5jj--
chapambuyo pa imfa nchokhwima
Zedi; ndipo sadzakhala ndi mtetezi
kwa Mulungu.
35. Fanizo la Munda wa
Mtendere umene Alonjezedwa
amene akuopa Mulungu (uli Tere:)
Pansi ndi patsogolo pake Ikuyenda
mitsinje. Zipatso zake ndi Mthunzi
wake nzanthawi zonse. Awa
Ndiwo malekezero a omwe akuopa
Mulungu; Koma malekezero a
osakhulupirira ndi Kumoto basi.
36. Ndipo (ena mwa) omwe
tidawapatsa mabuku (Ayuda ndi
Akhrisitu), akusangalalira Zimene
zavumbulutsidwa kwa iwe (ndipo
Akulowa m'Chisilamu). Koma ena
mu unyinji Wa osakhulupirira
akukana gawo lina la Nkhaniyi.
Nena: "Ndalamulidwa
kupembedza Mulungu basi; ndi
kusamphatikiza (ndi China).
Ndikuitanira kwa Iye,ndipo kwa
lye ndiwo mabwerero anga."
37. Ndipo momwemo
taivumbulutsa (Iyi Qur'an)
m'Chiarabu Kuti ikhale chilamulo
(cha Mulungu). Ngati utsata
zofuna zawo pambuyo Pokufika
kuzindikiraku,sudzakhala ndi
bwenzi Ngakhale mtetezi kwa
Mulungu.
38. Ndipo ndithu, tidatuma
atumiki, patsogolo pako Iwe
usanadze ndipo tidawalola kukhala
\ 9 C 9 m £\ J *\*1**K **""{ *
Surat 13. Ar-Ra'd Juzu 13
525
>r t&\
\ T op^Ji 5jj--
Ndi akazi ndi ana; (sichachilendo
iwe Kukhala ndi akazi ndi ana).
Ndipo Nkosatheka kwa Mtumiki
kudzetsa chozizwitsa Koma
pokhapokha ndi chilolezo cha
Mulungu. Nyengo iliyonse ili ndi
lamulo lake Limene Mulungu
adalilemba. (Nyengoyo Ikakwana,
lamulo limadza).
39. Mulungu amafafaniza
zimene wafuna ndi Kulimbikitsa
(kuti zisachoke zomwe wafuna),
Ndipo gwero la malamulo onse lili
kwa Iye(Mulungu).
40. Ndipo ngati tikusonyeza
zina mwa (zilango) Zimene
tawalonjeza, kapena kukupatsa
Imfa (usanazione zilangozo,
ndithu, Ziwafikabe).Ndithu udindo
wako ndi kufikitsa Uthenga basi
(umene walamulidwa kuufikitsa
Kwa iwo). Ife udindo wathu ndi
kuwerengera (Zochita zawo).
41. Kodi sadaone kuti
tikulidzera dziko lawo Ndi
kulichepetserachepetsera malire
ake? Ndipo Mulungu amalamula
(mwachilungamo) Palibe wotsutsa
lamulo Lake. Ndipo lye
Ngwachangu pakuwerengera.
42. Koma amene adalipo kale
iwo kulibe, Adachita ziwembu;
koma kuononga Ziwembu zonsezo
nkwa Mulungu basi. (lye)
Surat 13. Ar-Ra'd Juzu 13 526 * T *&\
^ t js-J\ ijj~>
akudziwa zimene cholengedwa
Chilichonse chachita. Ndipo
osakhulupirira Adzadziwa zotsatira
zabwino za Nyumba ya tsiku la
chimaliziro kuti Zidzakhala zayani.
43. Ndipo amene
sadakhulupirire akuti iwe Sindiwe
mtumiki. Nena: "Mulungu
Akukwanira kukhala mboni pakati
panga Ndi pakati panu (kuti ine
ndine Mtumiki), ndiponso aja
omwe ali ndi Nzeru ya m'Buku."
(Monga ena mwa Ayuda ndi
Akhrisitu omwe Adalowa
Chisilamu).
ejM&$to$£Z
Surat 14. Ibrahim Juzu 13
527
ST *>i
^ i *-a^S «jj-»
Siirat Ibrahim XIV
M'dzina la Mulungu waChifundo
Chambiri, waChisoni.
1. Alif-Ldm-Ra. (Hindi) Buku
lomwe talivumbulutsa Kwa iwe
kuti uwatulutse anthu mumdima
Ndikuwaika mkuunika -
mwalamulo la Mbuye wawo -
uwapititse kunjira ya Mwini
Mphamvu zoposa, Woyamikidwa.
2. Mulungu, Yemwe ndi Zake
zonse zakumwamba Ndi pansi.
Ndipo kuonongeka ndi Chilango
chokhwima kudzatsimikizika Pa
osakhulupirira.
3. Amene akukondetsa moyo
wadziko lapansi Kuposa moyo wa
pambuyo pa imfa, ndipo
Amatsekereza (anthu) kunjira ya
Mulungu ndikufuna kuikhotetsa
(pom we Njirayo njosakhota). Iwo
ali Mkusokera kotalikana
kwambiri (ndi Choonadi).
4. Ndipo sitidamtume Mtumiki
aliyense Koma ndi chiyankhulo
cha anthu ake Kuti awafotokozere.
Kenako Mulungu Akumsiya
kusokera amene wamufuna
(Chifukwa mwiniwake safuna
kuongoka). Ndipo amamuongolera
yemwe wamfuna, Ndipo lye
Ngwamphamvu zoposa,
Ngwanzeru zakuya.
Q^j)!<ijU#l«ti>L.
**ub
' »-"»^<fi^ , '' 'ii£i .'*!?£» '""'i
Surat 14. Ibrahim Juzu 13
528
>r *>i
S i f*-Aly! ^j-*»
5. Ndipo ndithu tidamtumiza
Musa ndi zozizwitsa Zathu
(tidamuuza):"Achotse anthu Ako
mumdima (waumbuli) ndi kuwaika
Mkuunika (kwa chikhulupiriro)
ndipo Uwakumbutse masiku a
Mulungu (a masautso)". Ndithu,
m'zimenezo muli zizindikiro kwa
Yense wopirira, wothokoza.
6. Ndipo (akumbutse anthu ako)
pamene Musa Adauza anthu ake: "
Kumbukirani mtendere Wa
Mulungu umene uli painu pamene
Adakupulumutsani kwa anthu a
Farawo, Omwe adakuzunzani ndi
chilango choipa. Ankazinga
(kupha) ana anu aamuna ndi
Kuwasiya amoyo ana anu aakazi;
ndithu, M'zimenezi mudali
mayeso aakulu ochokera Kwa
Mbuye wanu."
7. Ndipo ( kumbukani) pamene
Mbuye wanu adalengeza kuti:
"Ngati muthokoza,
ndikuonjezerani; Ndipo ngati
simuthokoza (Dziwani kuti)
chilango Changa nchaukali."
8. Ndipo Musa adati (kwa anthu
ake): "Ngati inu mukana(pakusiya
kuthokoza) Pamodzi ndi onse
am'dziko, (Mulungu salabadira
chilichonse Pazimenezo), ndithudi
Mulungu Ngwachikwanekwane;
Ngotamandidwa.
A
Siirat 14. Ibrahim Juzu 13 | 529 \>T *>i S i ^\y\ *jy
9. Kodi siidakudzereni nkhani
ya omwe Adalipo patsogolo panu?
Anthu a Nuhi, Adi ndi Samud?
Ndi omwe adadza Pambuyo pawo?
Omwe palibe akuwadziwa
Kupatula Mulungu. Atumiki awo
adawadzera Ndi maumboni
oonekera. Koma adabwezera
Manja awo kukamwa kwawo
(kusonyeza Kutsutsa), ndipo adati:
"Ndithu, ife Tikuzikana zimene
Mwatumizidwa nazo, ndipo Ife tili
m'chikaiko pazimene mukuitanira.
Ndiponso mchipeneko."
10. Aneneri awo adati: "Kodi
mwa Mulungu, Mlengi wa thambo
ndi nthaka muli chikaiko? lye
akukuitanani kuti akukhululukireni
Machimo ami, ndikuti
(mukakhulupirira) Akupatseni
nthawi (pokutalikitsirani Moyo
wanu) kufikira panthawi
yoyikidwa." Adati: "Inu sikanthu
kena koma ndinu anthu Ngati ife.
Mungofuna kutitsekereza
Kuzimene ankazipembedza
makolo athu; Choncho
tibweretsereni umboni woonekera."
11. Aneneri awo adati kwa iwo:
"(Zoonadi), Ife ndife anthu ngati
inu,koma Mulungu Amamchitira
zabwino yemwe wamfuna Mwa
akapolo Ake. Ndipo ife tilibe
Nyonga zokubweretserani
chisonyezo Koma mwachilolezo
«W*3fe
V
Surat 14. Ibrahim Juzu 13
530
>r ^
\ i A-AljJJ 0jJ~*
cha Mulungu. Ndipo Kwa Mulungu
yekha atsamire Asilamu onse."
12. "Nanga kwa ife kuli chiyani
kuti Tisatsamire kwa Mulungu
Pomwe watisonyeza Njira zathu.
Ndipo tipirira pa Zimene
mukutisautsa nazo. Choncho, kwa
Mulungu yekha atsamire otsamira."
13. Ndipo amene
sadakhulupirire, adanena Kwa
Atumiki awo: "Ndithu,
tikukutulutsani M'dziko lathu,
pokhapokha mubwerere
M'chipembedzo chathu." Koma
Mbuye wawo (Mulungu)
adawavumbulutsira uthenga
(Wakuti): "Ndithu, tiwaononga
Ochita zoipa (osakhulupirira)".
14. "Ndipo tikukhazikani (inu)
Pambuyo pawo m'dzikomo. Apeza
zimenezi omwe aopa Kuimirira
pamaso pa Ine, ndi kuopa
Machenjezo Anga."
15. Ndipo (aneneriwo)
adapempha chithandizo (Kwa
Mulungu), ndipo adaonongeka
Aliyense wodzikuza, wamakani.
16. (Yemwe) kutsogolo kwake
Jahannama ikumdikira, ndipo
(kumeneko) Adzamumwetsa
madzi amafinya (otuluka
M'matupi a anthu a kumoto).
17. Adzakhala akumwa Koma
movutikira Ndipo ululu wa imfa
^m^o^m
4&
°v:^
«S^£5%JS%&gK
Surat 14. Ibrahim Juzu 13
531
>r ijk\
^ t psA\y.\ «jj->
Udzamdzera mbali zonse koma
Sadzafa; ndipo kuonjezera apo,
Pali chilango (china) chaukali.
18. Fanizo la amene
sadakhulupirire Mbuye Wawo,
zochita zawo (zabwino zomwe
Sadzalipidwa nazo chabwino
chilichonse Chifukwa chakuti
sadazichite pofuna Kukondweretsa
Mulungu) zili ngati phulusa lomwe
likuulutsidwa ndi mphepo ya
mkuntho: ndipo sadzatha
kupindula chilichonse pa zimene
adachita, uko ndikutaika konka
nako kutali (ndi choonadi).
19. Kodi siuona kuti Mulungu
adalenga thambo Ndi nthaka
mwachoonadi? Ndipo atafuna
Angakuchotseni (nthawi imodzi)
ndikubweretsa Zolengedwa zina
zatsopano.
20. Ndipo zimenezo kwa
Mulungu sizovuta.
21. Ndipo onse (adzatuluka
m'manda mwawo ndiponso)
Adzakaonekera kwa Mulungu
(kuti awalipire). Pamenepo ofooka
(omwe adasokera chifukwa
Chotsatira atsogoleri awo)
adzanena kwa Omwe ankadzikuza:
"Ndithu, ife tidali Kukutsatirani
inu; kodi inu simungathe
Kutichotsera kachinthu kochepa
m' chilango Cha Mulunguchi?"
&O0
Surat 14. Ibrahim Juzu 13
532 ir*>i
1 t ^1^1 OjJ-M
(Atsogoleri) adzati: "Mulungu
akadationgolera,
tikadakuongolerani; (Koma
tsopano) ndi chimodzimodzi kwa
ife Titekeseke ndi chilangochi,
kapena tipirire Nacho; tilibe
pothawira."
22. Ndipo Satana adzanena
chiweruzo chikadzalamulidwa (Oipa
kulowa kumoto, abwino Kulowa
kumunda wamtendere): "Ndithu
Mulungu Adakulonjezani lonjezo
loona (ndipo Wakwaniritsa). Nane
ndidakulonjezani, Koma
sindidakukwaniritsireni. Ndidalibe
Mphamvu pa inu
(yokukakamizirani kunditsata)
Koma ndimangokuitanani basi,
ndipo Munkandiyankha. Choncho
musandidzudzule, Koma
dzidzudzuleni nokha. Sindingathe
Kukuthangatani ndiponso inu
simungathe Kundithangata. Ndithu,
ine ndidakukana Kundiphatikiza
kwanu ndi Mulungu kale. Ndithu,
ochita zoipa adzapeza chilango
Chowawa."
23. Ndipo amene adakhulupirira
ndikuchita zabwino,
<*^^\p\&$&%
Omasulira Qur'an adati: Chiweruzo chikadzaweruzidwa, anthu abwino
nkukakhazikika kumunda wamtendere pomwe anthu oipa kukalowa kumoto,
anthu akumoto adzayamba kumadzudzula Satana ndi kumnyoza. Ndipo
Satana adzaimirira pakati pawo pagome lamoto m'katikati mwa Jahannama
nadzanena kwa anthu onse akumoto kuti: "Musandidzudzule, koma dzudzulani
mitima yanu. Mitima yanu ndiyomwe idakuonongani. Ine ndinkangokuitanani
chabe, sindidakukakamizeni".
Surat 14. Ibrahim Juzu 13
533 h^>>
\ t +~*\jl\ *JJ~>>
Adzalowetsedwa kuminda yomwe
pansi Ndi patsogolo pake mitsinje
ikuyenda, Adzakhala m'menemo
muyaya mwachilolezo cha Mbuye
wawo. Kulonjerana kwawo
m'menemo Kudzakhala:
"Mtendere! "
24. Kodi suona momwe
Mulungu waponyera Fanizo la
liwu labwino? Liwu labwino Lili
ngati mtengo wabwino (umene)
mizu Yake njolimba, ndipo
nthambi zake zanka Kumwamba,
25. Umapereka zipatso zake
nthawi iliyonse Mwachifuniro cha
Mbuye wake. (Umo ndi momwe
Liwu labwino lilili, limabwera ndi
Zabwino). Ndipo Mulungu
amaponyera anthu Mafanizo kuti
akumbukire.
26. Tsono fanizo la liwu loipa,
lili ngati Mtengo woipa, umene
Wazulidwa m'nthaka omwe Uli
osalimba.
27. Mulungu amawalimbikitsa
amene Akhulupirira ndi mawu
olimba m'moyo Wadziko lapansi,
ndi moyo wapambuyo Pa imfa;
ndipo Mulungu amawalekerera
kusokera Omwe akudzichitira
okha zoipa; ndipo Mulungu
amachita zimene wafuna.
28. Kodi sudawaone omwe
asintha mtendere wa Mulungu
W#fZ2$$&$$&$
Surat 14. Ibrahim Juzu 13
534
S T *j£-l S t p-»\j>l 5j>-»
moukana ndikuwafikitsa anthu
awo (Omwe adawatsata m'zoipa)
kunyumba ya Chionongeko?
29. (Yomwe ndi) Jahannama;
Adzailowa; taonani Kuipa malo
okhazikikapo!
30. Ndipo ampangira Mulungu
anzake kuti Asokeretse (anthu)
kunjira Yake! Nena: "Sangalalani
pang'ono chabe! Ndithu,
kobwerera kwanu nkumoto!"
31. Auze akapolo Anga amene
akhulupirira Kuti apemphere swala
ndikupereka zina Mwazomwe
tawapatsa, mobisa ndi moonekera
Lisanawafike tsiku lopanda
(chithandizo Cha) kudziombola
ndi (chithandizo Cha) ubwenzi.
32. Mulungu ndiYemwe
adalenga thambo ndi Nthaka,
ndipo adatsitsa madzi ku mitambo,
Ndi madziwo adatulutsa zipatso
kuti zikhale Riziki lanu (chakudya
chanu) Ndipo adakufewetserani
zombo Kuti ziziyenda panyanja
mwa Lamulo Lake; ndiponso
adakufewetserani Mitsinje.
33. Adakufewetseraninso
dzuwa ndi Mwezi, mopitirira
(nthawi zonse) Ndiponso
adakufewetserani Usiku ndi usana.
34. Ndipo wakuninkhani
zimene mwampempha (Ndi
zimene simudam'pemphe). Ngati
®&M&&P$
U&Z&xS&fSZ
Surat 14. Ibrahim Juzu 13
535
\T tj*r\
> i *-Ai^S *jj**
Mutayesa kuwerenga madalitso a
Mulungu, simungathe
kuwawerenga. Ndithu, munthu
ngwachinyengo Chachikulu
ngosathokoza.
35. Ndipo (kumbukani) pamene
Ibrahim adanena: "Mbuye wanga!
Uchiteni mzinda uwu (Wa Makka)
kukhala wamtendere; Ndipo
ndipatuleni ine ndi ana anga
Kumachitidwe opembedza
mafano."
36. "Mbuye wanga! Ndithu,
(mafano) Awa asokeretsa anthu
ambiri. Choncho Amene
wanditsata, ndithu iyeyo ali mwa
ine (Mudzamulipira chabwino
monga Mwandilonjeza), ndipo
amene wandinyoza, (Mutha
kumukhululukira) ndithu Inu
Ngokhululuka kwambiri
Ngwachisoni."
37. "Mbuye wanga! Ndithu ine
ndaikhazika Ina mwa mbumba
yanga (mwana wanga Ismail)
pachigwa ichi (cha Makka)
Chopanda zomera panyumba yanu
Yopatulika (Al-ka'ba); Mbuye
Wathu (aloleni) kuti akhale
opemphera Swala; Choncho
ichiteni mitima ya anthu kukhala
Yopendekera kwa iwo (akonde
kudzakhala Malo amenewo), ndipo
apatseni Zipatso kuti athokoze."
ft&4&
* 9&S9*' 9}<"<
Surat 14. Ibrahim Juzu 13
536
>r *jJh
) t +*A\ji\ «JJ~»»
38. "Mbuye wathu! Ndithu Inu
mukudziwa Zimene tikubisa ndi
zomwe tikuonetsa Poyera. Ndipo
palibe chilichonse Chobisika kwa
Mulungu, m'dziko kapena
Kumwamba.
39. "Kuyamikidwa konse nkwa
Mulungu Yemwe Wandipatsa ine
kuukulu Ismail ndi Isihaka.
Ndithu,Mbuye wanga Ngwakumva
Pempho (la kapolo Wake)."
40. "Mbuye wanga! Ndichiteni
kukhala Wopemphera swala
pamodzi ndi mbumba Yanga.
Mbuye wathu! Landirani
Zopempha zanga."
41. "Mbuye wathu!
Ndikhululukireni ine Ndi makolo
anga ndi amene akhulupirira,
(Makamaka) patsiku la
chiwerengero (Kiyama)!.
42. Ndipo usaganize kuti
Mulungu waiwala zomwe
Akuchita oipa. Ndithudijye
akuwalekerera Chabe mpaka tsiku
lomwe Maso awo adzatong'oke
(Chifukwa cha mantha), 1
43. (Adzakhala) akuyenda
mothamanga mitu ili M'mwamba
ndipo maso awo osatha kuphethira,
tertL* ir^J Irtrff* {&** lOj
1 Ndithudi machitidwe a Mulungu nkuwalekerera oipa pamene akuchita zoipa.
Sawalanga mwachangu. Koma akafuna kuwalanga amawakhaulitsa ndi
chilango choopsa. Choncho munthu asanyengedwe pamene akulakwira
Mulungu namulekerera osamulanga.
Surat 14. Ibrahim Juzu 13
537
ir *>i
\ t f-A'y! 5jj-*»
Ndipo m'mitima mwawo muli
mopanda kanthu (Mopanda ganizo
lililonse chifukwa cha
Kudzadzidwa ndi mantha).
44. Ndipo achenjeze anthu za
tsiku lomwe Chilango
chidzawadzera; ndipo amene
Ankadzichitira okha zoipa
adzakhala akunena: "Mbuye
wathu! Tichedwetseni kanthawi
Kochepa (tipatseninso mwawi kuti
tibwerere Pa dziko); tikayankhe
kuitana kwanu ndi Kuwatsata
Atumiki." (Adzauzidwa): "Kodi
simunkalumbira kale kuti inu
Simudzachoka (pa dziko)?
45. "Chikhalirecho mudakhala
m'malo mommuja Mwa omwe
adadzichitira okha zoipa; ndipo
Kudaonekeratu poyera kwa inu
mmene tidawachitira
(Powaononga); ndipo
tidakufotokozerani Mafanizo
(osiyanasiyana koma inu
mudatsutsa)"
46. Ndithudi, adachita ziwembu
zawo, koma ziwembu Zawo zili
kwa Mulungu (akuzidziwa
bwinobwino); Ndipo ziwembu
zawozo ngakhale zitatha
Kuchotsetsa mapiri (sangamchite
kanthu Mtumiki
Muhammad {SAW} popeza
Mulungu Wamteteza).
^wjfejsayy^i
%
■si' 'Ai.'" »*y >\ \"\
titer
Surat 14. Ibrahim Juzu 13
538
>r *>i
) t f-*'^! «jj-*»
47. Choncho usaganize kuti
Mulungu Ngwakuswa Lonjezo
Lake kwa Aneneri Ake. Ndithu,
Mulungu ndi mwini Mphamvu
(salephera Chilichonse),
Ngobwezera chilango mwaukali.
48. (Likumbukireni) tsiku
lomwe nthaka iyi Idzasinthidwa
kukhala nthaka ina (Yachilendo),
ndi thambonso (lidzakhala Lina),
ndipo iwo (anthu onse adzatuluka
M'manda mwawo) adzaonekera
pamaso pa Mulungu Mmodzi
Wamphamvu (zopanda malire);
49. Ndipo oipa udzawaona
Tsiku limenelo Atanjatidwa ndi
unyolo;
50. Zovala zawo zidzakhala
zaphula, ndipo Moto udzavindikira
nkhope zawo;
51. Kuti Mulungu aulipire
mzimu uliwonse Pa zomwe
udakolola; ndithu; Mulungu
Ngwachangu pakuwerengera.
52. Izi zikukwana kukhala
phunziro kwa Anthu kuti
achenjezedwe nazo, ndi kuti
Azindikire kuti lye (Mulungu) ndi
Mulungu Mmodzi basi, ndikuti eni
nzeru akumbukire.
&$w*&ypte&3&
~ JM W'.Z
&*#>£&'
J&^ij&Jy^&Z&Z
3?"
&&^VuZ&&\6M
VWit
M3i
Surat 15. Al-Hijr Juzu 14
539
>t t$r\
> j*t}~\ djj~>
SURAT AL-HIJR XV
Sura yolemekezeka ikulongosola zoyenera mwa zilango
zomwe zidawatsikira anthu amibadwo yakale chifukwa
chakunyoza kwao Atumiki a Mulungu. Ndipo ikufotokozanso
nkhani za Aneneri akale ndi mavuto omwe adawapeza kwa
anthu awo. Ndiponso ikusonyeza za Mulungu ndi za
chilengedwe monga thambo lotukuka lokhala ndi nyenyezi ndi
nthaka yoyalidwa bwino ngati mphasa momwe mkati mwake
muli mapiri ataliatali olimbitsa nthaka.
Surayi ikufotokozanso za mphepo yomwe imatenga madzi
ndi kuwafalitsa panthaka; yomwenso imabereketsa mitengo.
Ndipo surayi ikupitirira ndi kulongosolanso za nkhondo yomwe
idalipo pakati pa Adam, Hawa ndi satana wopirikitsidwa
kuchifundo cha Mulungu; nkhondo yomwe ikupitirirabe mpaka
pa tsiku la chimaliziro. Ndipo nkhondoyi njomenyana pakati pa
chabwino ndi choipa. Malekezero ake adzakhala oipa kukalowa
kumoto, abwino kukalowa kumtendere.
Surat 15. Al-Hijr Juzu 14
540
U *>i
> o j3*J-l 5jj->
Surat Al-Hijr XV
ms ; ,,m&
:t
M'dzina la Mulungu waChifundo
Chambiri, waChisoni.
1. Alif-Ldm-Rd. Izi ndi aya za
M'Buku (lomwe lasonkhanitsa
chilichonse Chofunika,)
lowerengeka momveka bwino.
2. Nthawi zambiri omwe
sadakhulupirire (Pamene
adzakhala mkati mwa moto)
Adzalakalaka kuti akadakhala
Asilamu (Pamoyo wapadziko
lapansi).
3. Asiye azidya (chakudya
monga momwe Zidyera nyama)
ndi kusangalala; ndipo
Chiyembekezo chiziwatangwanitsa
ndi Kuwanyenga; posachedwa
adziwa (Kuti zimene
amaziyembekezerazo Nzabodza).
4. Ndipo sitidaononge mudzi
uliwonse (M'midzi yochita zoipa)
koma udali ndi Nthawi yake
(youwonongera) yodziwika.
5. Ndipo palibe mtundu wa
anthu umene Ungaitsogolere
nthawi yake (yofera) Kapena
kuchedwa (itakwana kale).
6. Ndipo (osakhulupirira)
akunena (Mwachipongwe) "E, iwe
amene Wavumbulutsiridwa ulaliki!
Ndithudi ndiwe wamisala.
ofa&\<£®\&\j
-^
f v \f ' \ , ^" j i.^'\»V l A' ' 9 J
^^MWKbK:
^S&sa
Surat 15. Al-Hijr Juzu 14
541
M t£-\
> j*i-l 3jj-»
^7m5&t&\
'9*.y
7. "Bwanji iwe osatibweretsera
angelo (Kuti akuchitire umboni)
ngati uli mmodzi Waonena
zoona?"
8. (Mulungu akuwauza) Ife
sititsitsa angelo Koma pokhapokha
(tikawatuma kukapereka Chilango
kuonongeka kwa anthu)
Kutatsimikizika (kuti
adzawaononge); Ndipo pamenepo
sangapatsidwe nthawi
9. Ndithu, Ife ndife omwe
Tavumbulutsa Qur'an, Ndipo
ndithudi, tiisunga. 1
10. Ndithudi tidatuma Atumiki
patsogolo Pako m'magulu (A
anthu) akale, oyamba.
11. Ndipo sadali kuwadzera
Mtumiki Aliyense, koma
ankamchitira chipongwe.
12. Momwemo tikuupititsa
(mkhalidwe Wachipongwewu)
m'mitima mwa oipa,
13. Koma saikhulupirira
Qur'aniyi chikhalirecho Mafanizo
a anthu oyamba awadutsa (Ndipo
aona momwe tidawaonongera).
1 Omasulira Qur'an adati Mulungu Mwini wake adalonjeza udindo woisunga
Qur'an ndi kuiteteza kuti anthu asathe kuikapo manja awo posintha
ndondomeko ya mawu ake kapena matanthandauzo ake, poonjezerapo
malembo ena kapena kuchepetsa monga momwe zidachitikira ndi mabuku
ena omwe Mulungu adawasiira anthu kuti awasunge ndi kuwateteza.
Qur'an yomwe tikuwerenga lero ndi yomweyo imene idalinso kuwerengedwa
m'nthawi ya Mtumiki Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale naye)
Palibe mawu oonjeza kapena kuchotsa.
©sis
Surat 15. Al-Hijr Juzu 14 542 U *>»
S j9^\ Ojj^t
14. Ndipo tikadawatsekulira
(awa osakhulupirira) Khomo
lakumwamba ndipo nkukhala
Akukwera m'menemo (ndi kutsika
monga Momwe amafunira kuti
zimenezo zikhale Chozizwitsa cha
Mtumiki)
15. Akadati: "Ndithu, maso
athu aledzera; (Iyayi) koma ndife
anthu olodzedwa (Tikuona zomwe
sindizo)." 1
16. Ndithudi, kumwamba
tidaikako "Buruji" (Momwe
zikuyendamo nyenyezi) ndipo
Tidakukongoletsa kwa okuwona.
17. Ndipo tidakuteteza kwa
satana aliyense Wopirikitsidwa
(kumwambako akafuna
Kukamvetsera zimene
zikunenedwa kumeneko).
18. Kupatula amene
amamvetsera mobera; Ndipo
pompo chinsakali chamoto
Choonekera chimamtsata.
19. Ndipo nthaka tidaiyala ndi
kuikamo Mapiri ndipo tameretsa
mmera wa Chinthu chilichonse
M'menemo mwamlingo (Wake).
20. Ndipo mmenemo
takupangirani zinthu Zoyendetsa
%&C&x$zMl$
fo'H&&
r^JiV-SJi *W^ jyw^oSj
®£& J=^ C^vJQ&p-ji
o^K*i\s f^<3J^^y[
1 Mulungu akuti akadawatsekulira makomo akumwamba monga momwe
adafunira nakwerako nkuona ufumu wa Mulungu ndi angelo ali yakaliyaklai,
sakadakhulupirirabe chifukwa chakuuma kwa mitima yawo. Chimene
akadanena nkuti mitu yazungulira.
Surat 15. Al-Hijr Juzu 14
543
W *>i
\ O j^J-l Ojj-*
moyo (wanu zakudya Ndi
zakumwa ndi zina zotere)
ndiponso (Tidakupatsani ana ndi
ziweto) zomwe inu Simungathe
kuzidyetsa. (Ife ndife amene
Tikuzikonzera chakudya chawo,
osati inu).
21. Ndipo palibe chinthu
chilichonse Koma gwero lake
likuchokera kwa Ife; Ndipo
sitichitsitsa koma mwamlingo
Wodziwika (osati
mwachisawawa) .
22. Ndipo timazitumiza mphepo
zitasenza madzi Ndipo madziwo
tikuwatsitsa kuchokera
Kumitamboyo; kenako
tikukumwetsani Madziwo
(tikukumwetseraninso ziweto zanu,
Mitengo yanu ndi zina), ndipo inu
siamene Mukuwasunga (madziwo).
23. Ndipo ndithudi, Ife ndife
omwe timapereka Moyo, ndi
kupereka imfa. Ndiponso Ife ndi
Amlowam'malo (a chinthu
chilichonse Chimene chikusiidwa
chopanda mwini).
24. Ndipo tikuwadziwa mwa
inu amene atsogola (Amene adafa
kale), ndipo tikuwadziwanso
Amene atsalira (ali ndi moyobe ndi
amene Sanabadwe).
25. Ndipo palibe chikaiko,
Mbuye wako ndi Yemwe
%?&&&&!?&$&
Surat 15. Al-Hijr Juzu 14 I 544 \ i *>
> jP^\ 5jj-*»
adzawasonkhanitsa (pambuyo pa
imfa Kuti adzawaweruze). lye ndi
Wanzeru Zakuya, Wodziwa
chilichonse.
26. Ndipo ndithu, tidamlenga
munthu ndi dongo Louma lolira
lochokera kumatope odera,
Osinthika mtundu;
27. Ndipo ziwanda tidazilenga
kale ndi Moto wamphepo yotentha
kwambiri.
28. Ndipo (kumbuka) pamene
Mbuye wako adauza Angelo
(kuti): "Ndithu, Ine ndilenga
munthu Ndi dongo louma lolira
lochokera Kumatope odera
osinthika mtundu;
29. "Choncho ndikamkwaniritsa
Ndikumuuzira mzimu
Wolengedwa ndi Ine,
muweramireni Momulemekeza".
30. Choncho angelo onse
Adamuweramira.
31. Kupatula Iblis; adakana
Kukhala mmodzi Mwa owerama.
32. Mulungu adati: "E, Iwe
Iblis! Chifukwa ninji sudakhale
Pamodzi ndi owerama?"
33. Adati: "Sindingamuweramire
Munthu yemwe mwam'lenga ndi
Dongo louma lolira lochokera
Kumatope odera osinthika
mtundu."
kn
®j&*
c^&Ja &QCjq\ uixi. o2S
Surat 15. Al-Hijr Juzu 14
545
> i ^jJt-1 > O yjJ-l Oj^
34. (Mulungu) adati: "Choncho
choka m'menemo; Ndithu, iwe
ndiwe wopirikitsidwa (ku
Chifundo changa).
35. "Ndipo ndithu,
matemberero ali pa iwe Mpaka
tsiku lamalipiro."
36. (Iblis) adati: "Mbuye wanga
choncho Ndipatseni nthawi mpaka
tsiku limene Adzaukitsidwe kwa
akufa."
37. (Mulungu) adati: "Ndithu,
iwe ndi mmodzi Mwa opatsidwa
nthawi (danga),
38. Kufikira tsiku la nthawi
yodziwika (Ikadzafika nthawi
imeneyo, udzafa)"
39. (Satana) adati: "Mbuye
wanga! Pakuti Mwanena kuti
ndine wosokera, choncho
Ndikawakometsera za m'dziko
(Kufikira kuti akakulakwireni)
Ndithu, ndikawasokeretsa onse,
40. Kupatula akapolo Anu
oyeretsedwa, Mwa iwo".
41. (Mulungu) adati: Iyi
ndinjira yoongoka Yobwerera kwa
Ine (ndipo adzandidzera
Akadzafuna).
42. Ndithudi akapolo Anga pa
iwo sudzakhala Ndi mphamvu
kupatula okutsata (Mwachifuniro
chawo) mwa opotoka."
Surat 15. AI-Hijr Juzu 14 546 \ t *j*-» \ ysJ-\ i^
43. Ndithu, Jahannama Ndiwo
malo awo Olonjezedwa kwa onse.
44. Hi ndi makomo asanu ndi
awiri; Ndipo khomo lililonse lili
ndi Gawo logawidwa mwa iwo.
45. Ndithudi oopa Mulungu
adzakhala M'minda ndi akasupe
(Omwe adzakhala Patsogolo
pawo),
46. (Ndipo tidzawauza)
"Lowani M'menemo
mwamtendere, Mosatekeseka."
47. Ndipo tidzawachotsera
mfundo Zachidani zomwe zidali
m'mitima Mwawo; (adzakhala)
mwachibale, (Mokondana,)
atakhala pamipando Yachifumu
atayang'anizana nkhope.
48. Mmenemo masautso
Sakawakhudza, Ndiponso
sadzatulutsidwamo.
49. Auze akapolo anga kuti
Ndithu Ine ndine Wokhululuka
kwambiri, Wachisoni.
50. Ndipo ndithu, chilango
Changa ndi chilango Chopweteka
zedi.
51. Ndipo auze nkhani ya
alendo a (Mneneri) Ibrahim.
52. Pamene adalowa kwa iye
ndikunena: "Salamu (Mtendere!
Iyenso adawayankha" "Mtendere
®&^&&4Xfe$&
Jfori
^4VS#&i&<8S
Surat 15. Al-Hijr Juzu 14 I 547 \i *j*-i ) y^\ 5j^
ukhalenso pa inu. "Ndipo Pamene
adaona kuti akana Chakudya)
Adati: "Ndithu ife tikukuopani."
53. (Iwo) adati: Usaope! Ife
tikukuuza Nkhani zabwino za (kuti
ubala) mwana Wanzeru
kwambiri."
54. (lye) adati:"Ha!
Mukundiuza nkhani Iyi pomwe
ukalamba wandifikira? Kodi
Nkhani yabwinoyi mukundiuza
m'njira Yotani?"
55. (Iwo) adati: "Takuuza
nkhani yabwinoyi Mwachoonadi;
choncho, usakhale mwa Otaya
mtima."
56. (lye) adati: "(I ne sinditaya
mtima Ndi chifundo cha
Mulungu). Ndithu, Palibe angataye
mtima ndi chifundo cha Mulungu,
koma wosokera basi (yemwe
Sazindikira ukulu wa Mulungu)."
57. (lye) adati: "Nanga
Cholinga chanu china Nchiyani, E,
inu otumidwa?"
58. (Iwo) adati: "Ife
Tatumidwanso kwa Anthu aja oipa
(kuti tikawaononge).
59. "Kupatula omtsatira Luti,
ndithu ife Tikawapulumutsa onse,"
60. "Koma mkazi wake (Wa
Luti), tampimira Kukhala mmodzi
wa otsalira pambuyo."
&&&mx$$$i
Surat 15. Al-Hijr Juzu 14
548
U t>i
> o j*J-\ ijj*j
61. Ndipo pamene atumikiwo
adadzera Anthu a Luti (okhala ali
ndi maonokedwe Aumunthu).
62. (Luti) adati: "Ndithudi, inu
ndi anthu Osadziwika
(sitikudziwani)."
63. (Iwo) adati: "Inde, ife
takudzera ndi zomwe (Iwo) adali
kuzikaikira, (zomwe ndi Chilango
chawo)."
64. "Ndipo tadza kwa iwe ndi
(chinthu) Choonadicho, ndithu ife
ndi oona (pazimene Tinenazi).
65. "Choncho, choka ndi banja
lako mkati Mwa usiku; ndipo iwe
udziwatsata Pambuyo pawo; tsono
aliyense wa inu Asayang'ane
kumbuyo (akamva mkokomo
Wachilango chochokera
kumwamba, kuopa Kuti angafe),
ndipo yendani (mwachangu)
Kunka komwe mukulamulidwa.
66. Ndipo tidamudziwitsa
iyeyo(Luti) lamulo lathu lakuti
ndithu phata lawo
anthu(ochimwawo)lidzadulidwa
kum'banda kucha .
67. Ndipo adadza (kwa Luti)
anthu a M'mudziwo akusangalala
(poona kuti Kwadza alendo okongola
kuti achite Nawo zadama). 1
^fti&Jlfc®
%gtt$%K
9&SC^&Ci$&£$£
?
K'
®v&03£^i$$&
1 Anthu a mumzindawo adadza kunyumba ya Luti akuthamanga mokondwa
atamva kuti kwa Luti kwadza alendo achinyamata owoneka bwino zedi.
Surat 15. Al-Hijr Juzu 14
549
^ t tji-i ^ o jp^\ Ojj~i
68. (Mneneri Luti) adati:
"Ndithu, awa Ndialendo anga;
choncho musandichititse Manyazi
(pochita nawo zadama)."
69. "Muopeninso Mulungu,
ndipo Musandichititse manyazi
(pamaso pawo),"
70. Iwo adati (kwa Mneneri
Luti): "Kodi Sitidakuletse
kulandira anthu (Achilendo)?"
71. (lye) adati: "Awa (akazi
onse ali ngati) Ana anga. Ngati inu
ndinu ochita (chimene
Chalamulidwa, akwatireni;
Musachite Zauve ndi alendowa)".
72. Ndikulumbira moyo wako,
ndithu Iwo m'kuledzera kwawo
(ndi zoipa) Akungoyumbayumba.
73. Choncho mkuwe wa
chilango udawagwira Pamene
dzuwa linkatuluka,
74. Ndipo (midziyo)
tidaigadabula kumwamba Kukhala
pansi, (pansi kukhala
Kumwamba); ndipo
tidawavumbwitsira Mvula
yamiyala (yotentha) yamoto.
75. Ndithudi, (m'nkhani iyi)
muli Malingaliro (aakulu) kwa
anthu olingalira Zinthu.
K&mi&$si®3s
%&%^J££
%&&&&&$%
®^M&mw&
%&&&&$&%&
%&J&2&\&8&
®&£M^£ttiM
Adabwera ndi cholinga chodzachita nawo zadama poganiza kuti alendowo
adali anthu monga iwo.
Surat 15. AI-Hijr Juzu 14
550
i 1 *j*-i > o y^t Sjj-*.
76. Ndipo (midzi) iyi (yomwe
tidaiwononga Chotereyi), ili
chikhalire m'njira Moyenda anthu
(ndipo iwo akuona Zizindikiro
zake)
77. Ndithudi, mzimenezi muli
phunziro (Lalikulu) kwa
okhulupirira.
78. Ndipo,ndithu, anthu a
m'nkhalango (Anthu a Mneneri
Shuaibu) Adali ochita zoipa
kwabasi;
79. Choncho, tidawalanga.
Ndipo (maiko) Awiriwa ali m'njira
zoonekera, (momwe Akuraishi
amadutsa pa maulendo awo).
80. Ndipo ndithu, okhala
m'chigwa cha Hijr, Adatsutsa
atumiki.
81. Tidawapatsa Zisonyezo
zathu, koma Sadazilabadire.
82. Iwo adali kujoba nyumba
m'mapiri Mwamtendere
(ankaboola mapiri Kuwasandutsa
nyumba zawo).
83. Choncho, chiphokoso cha
chilango Chidawapeza m'mawa.
84. Sichidawathandize (chuma)
chomwe Ankachipeza
(ngakhalenso zimene Ankazichita).
85. Sitidalenge thambo ndi
nthaka ndi (Zonse) zapakati pake
wjwras
®
&£&&?****''" lMf '-
\x<y®\z<s&a$@&Z
Surat 15. Al-Hijr Juzu 14
551
> t frj*-l ^ ygJ-\ Ojj-*
koma (Kulimbikitsa) choonadi.
Ndipo palibe chikaiko, Kiyama
idza. Choncho Mkhululukire
kukhululuka kwabwino, (Aliyense
wokuchitira zoipa).
86. Ndithudi, Mbuye wako, lye
ndi Mlengi Wa zonse, Wodziwa
kwambiri.
87. Ndipo ndithu, takupatsa
(Aya izi) zisanu ndi Ziwiri
zomawerenga kawirikawiri, (Surat
Fatiha), ndi Qur'an yolemekezeka.
88. Usatong'olere maso ako
(kuyang'ana) Zimene
tawasangalatsa nazo
Mitundumitundu ya mwa iwo
(monga chuma Cha anthu
osakhulupirira).
Usawadandaulirenso iwo ndipo
tsitsa phiko Lako kwa
okhululupirira, (uwafungatire
Monga nkhuku ichitira ndi ana ake).
89. Ndipo nena: "Ndithu, ine
ndine Mchenjezi woonekera,
(sindibisa chilichonse Kuopera
kuti chingakugwereni chilango
Cha Mulungu.)"
90. Monga momwe Tidatsitsira
(chilango) Kwa amene adadzigawa
m'magulu.
91. Omwe aichita Qur'an
Kukhala zigawozigawo; (Zina
nkuzikhulupirira, Zina
nkuzitsutsa).
^£&U Ji,e£££ &oJ£$
*^2&0&&
Surat 15. AI-Hijr Juzu 14 552 > i *>*
\ j*J-\ djj^
92. (Mulungu akuzilumbirira
kuti) pali Mbuye wako,
tidzawafunsa onse (Tsiku la
Kiyama),
93. Pazimene ankachita
(Padziko lapansi)
94. Choncho, lengeza zimene
ukulamulidwa, Ndipo uwapewe
Amshirikina, (usaope Chilichonse
kwa iwo).
95. Ndithu, Ife tikukwanira
kukuteteza Ku (zoipa za)
achipongwe.
96. Omwe akupanga milungu
Ina ndi kuiphatikiza Ndi Mulungu,
posachedwapa adziwa.
97. Ndithu, Ife tikudziwa kuti
chifuwa Chako chikubanika ndi
Zimene akunenazo.
98. (Koma pirira), lemekeza
Mbuye wako Pamodzi ndi
kumtamanda (ndi mbiri Zake
Zabwino) ndipo khala mwa
olambira (Mulungu.)
99. Ndipo mpembedze Mbuye
wako mpaka Chikufike
chitsimikizo (imfa).
&S9 *>< 9 9+f'*^ 'V*"<
%^\&&<$&i
®d^<eS^(l>^o^S
Surat 16. Al-Nahl Juzu 14
553
\ i *jA-l \ 1 J>lJ| Sj^-
SURAT AN-NAHL XVI
v~ ~fc . i .
Sura iyi idavumbulutsidwa ku Makka, kupatula aya zitatu
zomalizira, zidavumbulutsidwa ku Madina. Kuchuluka kwa aya
zake ndi 128.
Surayi yayamba ndi kulimbikitsa lonjezo la Chauta
lachilango cha opembedza mafano. Ndipo yafotokoza za
mphamvu za Mulungu pokwaniritsa zimenezo, komanso umboni
wosonyeza kukhoza kwake, ndi kulenga kwake kwa thambo ndi
nthaka.
Kenako surayi yafotokoza za chisomo cha Mulungu chomwe
chili pa anthu onse; monga powalengera ngamira ndi
kuwameretsera mbewu ndi zomwenso adawalengera m'nyanja;
monga nsomba zomwe iwo amadya, ndi majuwere
(zozikongoletsera nazo zamtengo wapatali monga ndolo makoza
zibangili ndi zina). Ndipo kenako surayi yalozanso zomwe
zingafunike pachisomo chimenechi, monga kuyamika Mulungu
ndi kupembedza lye yekha.
Yafotokozanso zakunyalanyaza kwa opembedza mafano, za
umodzi wa Chauta ndi kuinamizira Qur'an pomati ndi nthano
zopeka za anthu akale. Ndipo Mulungu waloza za chilango cha
Amshirikina patsiku la Kiyama, ndi za mtendere wa
okhulupirira.
Mulungu msurayi wafotokozanso mwatsatanetsatane kuti
opembedza mafano akutsutsa zouka ku imfa.
Surat 16. Al-Nahl Juzu 14
554 1 * *>'
> "V >Ji 3 jj-
Surat Al-Nahl XVI
3 r
«2
Q^JJI^JJI^I^.
v^hj
'tUfcWfti
M'dzina la Mulungu waC hi/undo
Chambiri, waChisoni.
1. Lamulo la Mulungu
lidzafika, (ndithu) Choncho,
musalifulumizitse; (ndipo
Khulupirirani kuti lye ndi
Mulungu) Woyera; Wopatukana
ndi mbiri zopunguka, Ndipo
watukuka ku Zomwe
akumphatikiza nazo.
2. Amatumiza Angelo pansi
pamodzi ndi Chivumbulutso mwa
lamulo Lake (Mulungu), Kwa omwe
wawafuna mwa akapolo Ake
(Powauza) kuti achenjezeni (anthu
zakuti) Palibe wopembedzedwa
mwachoonadi koma Ine ndekha,
choncho ndiopeni."
3. Adalenga thambo ndi nthaka
mwachoonadi (Osati
mwakungoseweretsa chabe) ndipo
Watukuka kuzimene
akumphatikiza nazo (Ophatikiza
Mulungu ndi mafano).
4. Adalenga munthu kuchokera
kudontho la Umuna; ha! kenaka iye
(munthuyo) Wakhala wotsutsana
naye (Mulungu) Woonekera. 1
1 Apa Mulungu akunenetsa kuti adalenga munthu kuchokera kudontho la
umuna wopanda pake. Koma munthu pambuyo pokwanira chilengedwe chake
akukhala wotsutsana ndi Mlengi wake ndi kumchitira mwano modzitukumula
chikhalirecho adalengedwa kuti akhale kapolo wa Mulungu, osati wopikisana naye.
m?&&Qzi\&L
Surat 16. Al-Nahl Juzu 14
555
U ^>>
\ n j^ji *jj~<
5. Ndipo adalenga ziweto
(monga ngamira, Ng'ombe ndi
mbuzi) mwa izo mukupeza
Zofunda, ndi zothandiza (zina
zambiri), Ndipo zina mwa izo
mumazidya
6. Ndipo mumakondwa ndi
kunyadira chifukwa cha
Kukongola kwa izo mukamabwera
nazo (Kuchokera kubusa mimba
zitakhuta), Ndi popita nazo
(kumunda ndi kubusa Zikuyenda
mwandawala).
7. Ndipo zimasenza mitolo yanu
(yolemera) kukafika Nayo kumidzi
yakutali komwe simumatha
Kukafikako popanda kuvutika
kwambiri.Ndithu, Mbuye wanu
Ngodekha kwabasi, Ngwachisoni.
8. (Adalenganso) akavalo,
nyumbu ndi abulu Kuti
muzizikwera ndi kutinso zizikhala
Chokometsera chanu (cholowetsa
chisangalalo M'mitima yanu);
ndipo adzalenga (zokwera Zina)
zomwe simukuzidziwa, (monga
galimoto, Sitima, ndege ndi zina).
9. Ndipo ndi udindo wa
Mulungu kusonyeza Njira
yolungama (yomwe
ingakufikitseni Kumunda
wamtendere), koma zilipo njira
Zina zokhota (zomwe sizifikitsa
kuchoonadi). Ndipo Mulungu
akadafuna, akadakuongolani
&r-- •*
Surat 16. Al-Nahl Juzu 14
556
>i »>l
> ■; j>jt Sj^
®,
Nonsenu (mwachifiiniro chanu ndi
mopanda Chifuniro chanu.Koma
lye adakupatsani nzeru Kuti
musankhe nokha njira imene
mufuna)
10. lye ndi Amene
akukutsitsirani madzi Kuchokera
kumitambo, madziwo mumamwa
(Pothetsa ludzu lanu), ndipo ndi
madziwo Mitengo imamera;
mitengo yomwe mumadyetsa
Ziweto (zanu).
11. Ndi madzi omwewo
amakumeretserani mmera,
(Mitengo ya) mzitona, kanjedza,
mpesa, Ndi mitundu ina yonse
yazipatso. Ndithu Kupezeka kwa
zimenezi ndi chisonyezo
(Chosonyeza mphamvu za
Mulungu) kwa Anthu olingalira. 1
12. Ndipo chifukwa cha inu
adagonjetsa usiku Ndi usana;
dzuwa ndi mwezi; (zonse
Zidalengedwa kuti zibwere ndi
zokomera inu). Nazo nyenyezi
zidagonjetsedwa mwa lamulo
Lake. Ndithu m'zimenezi muli
zizindikiro Kwa anthu anzeru.
13. Ndiponso ndi zimene
adakulengerani m'nthaka (Zinthu
1 Ndithudi, m'kutsika kwa madzi kuchokera kumitambo ndi ku me rets a zipatso,
muli zisonyezo zoonekera poyera kukhoza kwa Mulungu ndi umodzi wake
kwa anthu omwe amalingalira za zolengedwa Zake. Ndipo potero
amakhulupirira Mulungu Kodi simukuona mbewu imodzi ikaikidwa m'nthaka
ndi kupitapo nyengo yodziwika, imafunafuna potulukira ndi kung'amba nthaka
ndi kukula kusanduka mtengo? Zonsezi nzododometsa kwa anthu olingalira.
U
^kj®dwB^
Sural 16. Al-Nahl Juzu 14
557 hi »>i
^ 1 >cJl J,^,
^avsr^asf^a
©,■'*'
'(aa>»oJ
©6$%2U&
zododometsa monga nyama,
mmera, Miyala yamtengo
wapatali, zamoyo ndi Zopanda
moyo), zautoto wosiyanasiyana ndi
Maonekedwe osiyanasiyana;
ndithu, M'zimenezo muli
zisonyezo kwa anthu Olalikika.
14. Ndipo lye ndi Yemwe
adagonjetsa nyanja Kuti mudye
nyama yamatumbi (ya) m'menemo
(Nsomba) ndikuti mutulutse
m'menemo Zodzikongoletsera
zomwe mumavala; ndipo Uona
zombo zikuluzikulu zikung'amba
(Mafunde) m'menemo kuti
mufunefune Zabwino zake (njira
ya malonda), ndi kuti Muthokoze
(Mbuye wanu Mulungu).
15. Ndipo adaika panthaka
mapiri ataliatali Kuti (nthaka)
isagwedezeke nanu; ndipo
(Adaika) mitsinje ndi misewu kuti
muongoke (Potsata njira yeniyeni
ndikukafika komwe Mukufuna). 1
16. Ndipo (adaikanso)
zizindikiro zina, Ndiponso
kupyolera m'nyenyezi, iwo
Amalondola njira.
17. Kodi Yemwe amalenga
angalingane ndi omwe Salenga?
1 Mulungu adakhazikitsa mapiri ataliatali, olimba kuti nthaka isamagwedezeke
pafupipafupi. Abu Suud adati: "Ndithudi nthaka idalengedwa ngati mpira
ndikukhala yogwedezeka pazifukwa zochepa asanailengere mapiri monga
momwe zimagwedezekera nyenyezi zinzake. koma pamene adailengera
mapiri idakhazikika. Zoterezi ndi pachifukwa chakuti anthu akhazikike bwino.
%:-"- '
®&&&J$&£&
<%3$®8^ufi§*&
Surat 16. Al-Nahl Juzu 14 558 U *>i ^ n J~Ji3j>-
Kodi simungakumbukire
(Ndikudziwa kulakwa kwanu
pomuyerekeza Mulungu ndi
mafano)?
18. Ngati mutayesera
kuwerengera mtendere Wa
Mulungu simungathe
kuuwerengera (Wonse); ndithudi,
Mulungu Ngokhululuka
Kwambiri, Ngwachisoni.
19. Ndipo Mulungu akuzidziwa
Zimene mukuzibisa, Ndi zomwe
mukuwonetsera.
20. Ndipo zomwe
mukuzipembedza kusiya Mulungu,
sizilenga chilichonse, ndipo Izo
nzolengedwa.
21. Zakufa zopanda moyo;
ndipo Sizizindikira kuti nliti akufa
Adzaukitsidwa (m'manda
mwawo).
22. Mulungu wanu ndi
Mulungu mmodzi Yekha; koma
amene sakhulupirira Za tsiku la
chimaliziro, mitima yawo Ikukana
(kukhulupirira umodzi wa
Mulungu), Ndipo iwo
akudzitukumula.
23. Palibe chikaiko, Mulungu
akudziwa zomwe Akubisa, ndi
zomwe akuzilengeza. Ndithudi,
lye sakonda odzikuza.
24. Ndipo (osakhulupirira)
akafunsidwa: Kodi Mbuye wanu
$' *99*~'X' '£X'9<V: 1$ i'*<
Surat 16. Al-Nahl Juzu 14
559
U *jk-\
) "V J*cJl 5jj-»
•*
watumizanji (kwa Mneneri
Muhammad{SAW})"? Akunena,
(sadatumize Chilichonse koma)
nthano zabodza za Anthu akale." 1
25. (Motero akuwasokeretsa
anthu) kuti Adzasenza mitolo
yawo (yamachimo) Yokwanira pa
tsiku la Kiyama, Ndiponso gawo
lamitolo ya omwe Akuwasokeretsa
popanda kuzindikira (Osokerawo).
Tamverani! Ndi yoipa Kwabasi
mitolo yomwe azikaisenza!
26. Adachita ndale omwe
adalipo Patsogolo pawo; choncho
Mulungu Adagumula maziko
anyumba zawo. Ndipo madenga
adawagwera Pamwamba pawo;
ndipo Chilango chidawadzera
Kuchokera komwe sadali
kukudziwa.
27. Kenako tsiku la Kiyama
adzawayalutsa Ndi kunena: "Ali
kuti omwe mudali Kundiphatikiza
nawo, omwe chifukwa cha Iwo
mudali kukangana (ndi
Mtumiki)?" Adzanena omwe
apatsidwa nzeru: "Ndithu,
Kuyaluka ndi tsoka loipa zili pa
Osakhulupirira lero,"
28. Omwe angelo akutenga
miyoyo yawo Atadzichitira okha
1 Omasulira Qur'an akunena kuti, amshirikina adali m'njira zolowera mumzinda
wa Makka ndi cholinga chopatula anthu kwa Mtumiki (SAW). Anthu odzachita
haji akawafunsa kuti:"Kodi nchiyani chavumbulutsidwa kwa Muhammad?" Iwo
amati: "Ndi nthano zabodza za anthu akale osati Mawu a Mulungu."
^SJSii&Ugte
2^ &&$£=£&
mm\&z;&$\
Surat 16. Al-Nahl Juzu 14 560 ^ t *>i
1 1 J~Jl 5j>w
zoipa (ponyoza Mulungu).
Choncho adzadzipereka (kwa
Angelowa, kuti atenge mitima
yawo Akunena:) "Sitidali kuchita
choipa Chilichonse." (Angelo
adzati:) "Zoona, Palibe chikaiko,
Mulungu akudziwa kwambiri
Zomwe munkachita;
29. Choncho, lowani makomo a
ku Jahannama; Mukakhala
m'menemo muyaya." Taonani
Kuipitsitsa kwa malo a anthu
odzikweza!
30. Ndipo kukanenedwa kwa
omwe akuopa Mulungu (kuti):
"Kodi nchiyani watumiza Mbuye
wanu?" Amati: "Zabwino." Kwa
omwe achita zabwino padziko ili
Lapansi, awapatsanso zabwino,
ndipo Nyumba Ya tsiku la
chimaliziro njabwino kwambiri,
Ndipo taonani ubwino wa Nyumba
Ya oopa Mulungu!
31. Minda yamuyaya
adzailowa, pansi pake Padzakhala
pakuyenda mitsinje ndi Patsogolo
pake, chokhumba chilichonse
Akachipeza mmenemo (popanda
kuchivutikira); Umo ndi momwe
Mulungu amawalipirira Omuopa
(iye),
32. Amene miyoyo yawo
angelo amaitenga Iwo ali
abwino,(angelo) akunena kuti:
"Mtendere uli pa inu, lowani
Surat 16. Al-Nahl Juzu 14 I 561 I \ t *>»
\ \ Jj»Ji djj~>
kumunda Wamtendere chifukwa
cha (zabwino) zija Zomwe mudali
kuzichita."
33. Kodi akuyembekezera
china, awa Osakhulupirira,
posakhala kuti angelo awadzere
Ndikuwaononga; kapena kuti
liwadzere Lamulo la Mbuye wako
(lakuwalanga)? Momwemo ndi
m'mene adachitiranso omwe
Adalipo patsogolo pawo. Koma
Mulungu Sadawachitire choipa
koma adadzichitira Okha choipa.
34. Choncho, zoipa za zomwe
adachita Zidawapeza, ndipo
Chilango chidawazinga Pa zomwe
ankazichita mwachipongwe.
35. Ndipo aja Amshirikina
akuti: "Mulungu Akadafuna,
sitikadapembedza chilichonse
Kusiya lye, ife ngakhale makolo
athu; Ndiponso palibe chomwe
tikadachiyesa Choletsedwa
popanda lamulo Lake."
Momwemo ndimo adachitiranso
aja omwe Adalipo patsogolo pawo.
Kodi atumiki Ali ndi udindo
winanso, osati kufikitsa Uthenga
woonekera (womveka?)
36. Ndipo ndithu, kumtundu
uliwonse tidatumiza Mtumiki
(amene amawauza kuti):
"Pembedzani Mulungu, ndi
kumpewa (Iblis) woipa: "Choncho
alipo ena mwa Iwo omwe
e^teS
I** *'**>>. 'fix /' ><>>9> <
Surat 16. Al-Nahl Juzu 14 562 > * *>*
> % >Ji Ojj-
Mulungu adawaongola, ndipo
alipo Ena mwa iwo omwe
kusokera kudatsimikizika Pa iwo.
Choncho yendani padziko
ndikuyang'ana (Kuti) kodi adali
bwanji Mathero a otsutsa.
37. Ngati uwumirira kwambiri
kuti uwaongole Komatu Mulungu
saongola Yemwe akusokeretsa
(Ena), ndipo sadzapeza
wowathangata.
38. Ndipo iwo adalumbirira
m'dzina la Mulungu, kulumbirira
kwawo kwamphamvu (Kuti)
Mulungu sadzaukitsa amene afa;
Nchotani (kuti asawaukitse?) Hi
ndi Lonjezo lokakamizika kwa lye,
(kuwaukitsa Ndi kuwalipira);
koma anthu ambiri sadziwa.
39. (Adzawaukitsa) kuti
Awafotokozere za Zomwe adali
kusiyana Ndi kuti amene
Sadakhulupirire Adziwe kuti
ndithu iwo adali abodza.
40. Ndithu liwu Lathu
pachinthu chimene Tikuchifuna
kuti chichitike ndikuchiuza Basi
kuti,"Chitika," ndipo
chimachitikadi.
41. Ndipo omwe adasamuka
chifukwa Cha Mulungu (kusiya
midzi yawo) pambuyo
Poponderezedwa (kumeneko,)
ndithu Tiwakhazika mwaubwino
*&^%&&&g
Surat 16. Al-Nahl Juzu 14 I 563 I \ t *jk-\
\ 1 J^cJi djj-i
padziko Lapansi; ndipo malipiro a
tsiku La chimaliziro (omwe
akuwayembekezera), Ngakulu
zedi, akadakhala akudziwa (Awa
oipa).
42. (Amene adzapeza zimenezi,
ndi) omwe Adapirira ndi kutsamira
kwa Mbuye wawo.
43. Ndipo patsogolo pako
(aneneri) omwe Tidawatuma
adalinso amuna, omwe
Tidawavumbulutsira
chivumbulutso. Choncho afunseni
eni chikumbumtima (Za
m'Mabuku a Mulungu akale) ngati
Inu simukudziwa.
44. (Tidabwera) ndi zisonyezo
Zoonekera pamodzi ndi mabuku;
Ndipo takuvumbulutsira ulaliki
kuti Uwafotokozere anthu Zomwe
zavumbulutsidwa Kwa iwo kuti
aganizire.
45. Kodi adziika pachitetezo,
amene Akuchita ndale zoipa, kuti
Mulungu Sangawakwirire ndi
nthaka, kapena Chilango
kuwadzera kuchokera komwe
Sadali kukudziwa (sadali
Kukuyembekezera)?
46. Kapena (Mulungu)
kuwathira dzanja Mkuyenda
kwawo kwa uku ndi uko? Pom we
iwo sangathe kumulepheretsa
Mulungu kuchita chomwe wafuna
pa iwo.
Surat 16. Al-Nahl Juzu 14
564 \ t *>»
> 1 J*dl 5^
47. Kapena kuwalanga uku ali
ndi mantha Oyembekezera
chilango (pakulanga
M'modzim'modzi kufikira onse
atatha)? Ndithu, Mbuye wanu
Ngodekha Ngwachisoni.
48. Kodi sadaone chinthu
chilichonse (molingalira)
M'zimene Mulungu adalenga
zomwe zithuzi Zake zimazungulira
kudzanjadzanja ndi Kumanzere,
kulambira Mulungu uku zili
Zodzichepetsa kwa lye? (Nanga
iwo Osakhulupirira akudzikweza
chotani pamaso pa Mulungu?)
49. Ndipo zimalambira
Mulungu zonse Zakumwamba ndi
zapansi, Nyama ndi angelo; Iwo
sadzikuza (pamapemphero).
50. Amaopa Mbuye wawo
Yemwe ali pamwamba Pawo;
ndipo amachita zokhazo zomwe
Alamulidwa.
51. Ndipo Mulungu wanena:
"Musadzipangire Milungu ina iwiri.
Ndithudi, lye ndi Mulungu mmodzi.
Choncho opani Ine ndekha".
52. Zonse zakumwamba ndi
pansi nza lye, Ndipo kumumvera
ndi kumugonjera nkwake Nthawi
zonse. Kodi muopa wina amene
sali Mulungu?
53. Ndipo mtendere wonse
umene muli nawo Udachokera kwa
o>
&&®t&fi^
Sri'**" 9 --< 9*9)4, S&y
Siirat 16. Al-Nahl Juzu 14 565 1 £ *>» in J~J» Sj^
Mulungu (koma inu Simuthokoza)
ndipo masautso akakukhudzani,
lye ndi amene Mumamulirira;
54. Koma akakuchotserani
masautso, Pompo gulu lina la mwa
inu limamphatikiza Mbuye wake
(ndi mafano).
55. Ncholinga choti akane
mtendere umene Tawapatsa,
choncho sangalalani pang'ono,
Posachedwapa mudziwa (mapeto a
zochita Zanu).
56. Ndipo gawo la zomwe
tawapatsa akuiikira (Milungu
yawo yabodza) yomwe siizindikira
Chilichonse. Tallahi,
(ndikulumbira Mulungu,) ndithudi,
mudzafunsidwa Pazimene
munkapeka.
57. Ndipo (mwaumbuli)
akumuikira Mulungu Ana aakazi
(ponena kuti adabereka ana
Aakazi) Subuhana! (Way era
Mulungu Kuzimenezi!) Ndipo iwo
(eni) Amadzifunira amene
amawakonda (Omwe ndi ana
achimuna)!
58. Ndipo mmodzi wawo
akauzidwa nkhani Ya (kuti
wabereka) mwana wamkazi
Nkhope yake imada, ndipo
amadzala Ndi madandaulo.
59. Amadzibisa kwa anthu
chifukwa Chankhani yoipa imene
$G&g*88WZ'
'&&$%&&\z&<&
^W^0^^
»t\*i'\»> \*% x sit'"''
Surat 16. Al-Nahl Juzu 14
566
U *>i
) *\ J*cJ» Sjj*
wauzidwa (Nayamba kulingalira)
kodi akhale Naye pamodzi
ndikuyaluka (pamaso pa Anthu),
kapena angomkwirira m'dothi (Ali
moyo)? Mverani! Ndi choipa
Kwabasi chiweruzo chawo. 1
60. Kwa awo amene
sakhulupirira za Tsiku la
chimaliziro, ali ndi mbiri Yoipa;
koma Mulungu ali ndi mbiri
Zapamwamba; ndipo lye
Ngwanyonga, Ngwanzeru zakuya.
61. Ndipo Mulungu akadakhala
akulanga anthu (Mwachangu)
pazolokwa zawo, Sakadasiya
ngakhale nyama imodzi
Pamwamba panthaka; koma
Akuwachedwetsera (chilangocho)
mpaka Panthawi yoikidwa; ndipo
ikadzadza Nthawi yawoyo,
sangathe kuichedwerera Ngakhale
ola limodzi; ndiponso sangathe
Kuifulumirira (ngakhale ola
limodzi.)
62. Ndipo akumuikira Mulungu
zimene (iwo) Akuzida (omwe ndi
ana aakazi Pomati Mulungu
adabala ana aakazi), Ndipo
* I'ii
>^J£
t)l^
Ophatikiza Mulungu ndi mafano adali kuda ana aakazi. Kubala mwana
wamkazi amachiona monga chochititsa manyazi pamaso pa anthu kotero kuti
ena mwa iwo akawauza kuti mkazi wawo wabala mwana wamkazi,
amakamkwirira mwanayo ali wamoyo chifukwa choopa kunyozedwa pamaso
pa anthu, pomwe iwo amawayesa angelo ngati ana aakazi a Mulungu.
Chimene amachida, amampachika nacho Mulungu, ndipo chomwe
amachikonda amati ndicho chawochawo. Izi nzamwano, zomwe
osakhulupirira adali kumuyankhulira Chauta.
Surat 16. Al-Nahl Ju/u 14
567
M *>»
1 1 JmaIi 5j>-
malirime awo akunena bodza Kuti
iwo adzapeza zabwino (kwa
Mulungu); palibe chikaiko, ndithu
moto Ndi wawo, ndipo iwo
adzasiidwa (Mmenemo).
63. Pali Mulungu! Ndithudi
tidatumiza (Atumiki) kumitundu
yomwe idalipo Patsogolo pako,
koma satana Adawakometsera
zochita zawo (Zoipa ankaziona
kuti nzabwino Napitiriza
kuzichita). Choncho lye (Satana)
ndi bwenzi wawo lero, (Koma pa
tsiku la chimaliziro, Adzadana
naye kwambiri), ndipo iwo
Adzapata chilango chowawa.
64. Ndipo sitidakutumizire
Buku (ili) Koma kuti
uwafotokozere zomwe
Akusiyanirapo ndi kuti (likhale)
Chiongoko ndi chifundo kwa anthu
Okhulupirira.
65. Ndipo Mulungu watsitsa
madzi Kuchokera kumitambo,
ndipo Akuipatsa moyo nthaka Ndi
madziwo (pomeretsa mbewu)
Pambuyo poti nthakayo idali
yakufa; Ndithu m'zimenezo muli
chisonyezo (Chosonyeza kukhoza
kwa Mulungu) Kwa anthu amene
amamva.
66. Palibe chikaiko, m'ziweto
muli Phunziro ndi lingaliro kwa
inu. Timakumwetsani zomwe zili
m'mimba Mwaizo, (zomwe
W*Si#a
*&&&&
m^%40$&
\99
Surat 16. Al-Nahl Juzu 14
568
M >>»
1 1 J~Jl 5j^
zimatuluka) pakati Pa ndowe ndi
magazi, (omwe ndi) Mkaka
woyera, wabwino wokoma kwa
Oumwa.
67. Ndipo kuchokera kuzipatso
za tende Ndi mphesa, mumakonza
zakumwa Zoledzeretsa (zomwe
nzoletsedwa) Ndikupezanso riziki
labwino (M'zipatsozo); ndithudi
m'zimenezo Muli lingaliro kwa
anthu oganiza Mwanzeru.
68. Ndipo Mbuye wako
adaizindikiritsa Njuchi kuti:
"Dzikonzere nyumba M'mapiri,
m'mitengo, ndi (m'ming'oma)
Imene (anthu) anakonza;
69. Tsono idya zipatso
zamtundu uliwonse Ndikuyenda
m'njira za Mbuye wako zimene
Wazifewetsa (kuziyenda);"
chimatuluka M'mimba mwake
chakumwa cha utoto
Wosiyanasiyana (uchi), mwaicho
muli Kuchilitsa kwa anthu
(kumatenda Ochuluka) ndithu
m'zimenezo muli lingaliro Kwa
anthu oganiza (zinthu) mwakuya.
70. Ndipo Mulungu
adakulengani, kenako
Akukupatsani imfa (nthawi ya
moyo Wanu ikatha); ndipo mwa
inu alipo ena Amene
akubwezedwa kumoyo woipa
(Waukalamba wogwa nkumina)
kotero Kuti asadziwe kanthu
©'
v&.
Surat 16. Al-Nahl Juzu 14
569 * i *>'
^ 1 J^dl 5j^
pambuyo Pakudziwa (zambiri);
ndithudi Mulungu Ngodziwa
kwambiri Wokhoza (chilichonse
chimene Afuna kuti chichitike).
71. Ndipo Mulungu wapereka
zopereka Zake mochuluka kwa ena
kuposa Ena; ndipo amene
apatsidwa Mochulukawo
sangagawire zopatsidwa Zawo
omwe manja awo Adzanjadzanja
apeza (akapolo awo) kuti Akhale
ofanana pa zopatsidwazo (Nanga
bwanji inu mukuti Mulungu
ngofanana ndi akapolo Ake
Pomwe inu simufuna kufanana ndi
akapolo Anu?) Nanga kodi
mtendere wa Mulungu akuukana?
72. Ndiponso Mulungu
adakulengerani akazi amtundu
wanu, ndipo adakupangirani Ana
ndi zidzukulu kuchokera mwa
Akazi anuwo; ndipo adakupatsani
zinthu zabwinozabwino, Kodi
akukhulupirira zachabe, ndi
Kuchikana chisomo cha Mulungu?
73. Ndipo akum'siya Mulungu
Ndikupembedza zomwe
sizingawapezere Zopatsa ngakhale
pang'ono, Zochokera kumwamba
ndi pansi Ndipo sizikhoza
chilichonse.
74. Choncho, musaponyere
mafanizo Mulungu. Ndithudi
Mulungu Akudziwa, pomwe inu
simudziwa (Chinsinsi cha zinthu.)
ill "wit ' X l '* ' '99) 9 S*
Surat 16. Al-Nahl Juzu 14
570 1 1 *>»
^ n jjuji ojj--
75. Mulungu akuponya fanizo
la (anthu Awiri: wina ndi) kapolo
wopatidwa (Wokhala pansi
paulamuliro wa Munthu wina);
yemwe alibe mphamvu
Pachilichonse; ndi (munthu)
yemwe Tampatsa zabwino
zochokera kwa Ife Ndipo iye
nkupereka rizikilo mobisa Ndi
moonekera; kodi angafanane
(Awiriwa? Nanga bwanji
Mukufananitsa Mulungu ndi
mafano?) Kuyamikidwa konse
nkwa Mulungu. Koma ambiri aiwo
Sadziwa (kuyamika Mulungu).
76. Ndipo Mulungu
waponyanso fanizo la Anthu (ena)
awiri: mmodzi ndi Bubu (wosatha
kulankhula), alibe Mphamvu pa
chilichonse; ndipo iye Ndi mtolo
wolemetsa chabe Mbuye Wake;
kulikonse kumene wamulunjikitsa,
Sabwerako ndi chabwino
(chifukwa cha Umbutuma wake).
Kodi iye angafanane ndi Yemwe
akulamula mwa chilungamo,
Yemwenso ali panjira yolunjika?
77. Ndipo chinsinsi cha (za)
kumwamba ndi (Za) pansi ncha
Mulungu yekha, (Iye ndiye Amene
akudziwa zochitika m'menemo,
Osati wina wake). Ndipo kuchitika
kwa Kiyama kuli ngati kuphetira
kwa diso, Kapena kufulumirirapo.
Ndithudi, Mulungu Ngokhoza
chilichonse.
!5-*>I ir^ 4 ^ 6?v^ ^£Sj>-
Surat 16. Al-Nahl Juzu 14
571 h t *>»
i n j^Ji Sjj-
78. Ndipo Mulungu
adakutulutsani m'mimba Mwa
amayi anu pomwe simudali
Kudziwa chilichonse; Ndipo
adakupatsani Kumva, kuona ndi
Mitima kuti muthokoze.
79. Kodi saona mbalame
mumlengalenga Zikugonjera
(Mulungu?) palibe amene
Akuzigwira (kuti zisagwe) koma
Mulungu yekha. Ndithudi
m'zimenezo Muli malingaliro kwa
anthu Okhulupirira.
80. Ndipo Mulungu
adakuikirani nyumba Zanu kuti
zikhale mokhala (mwanu)
Ndiponso adakupangirani zikopa
za Ziweto (kukhala zotheka
kuzikonza) Kukhala nyumba,
zomwe mumaziona Kuti
nzopepuka kuzitenga panthawi Ya
ulendo wanu ndi panthawi ya
Kukhazikika kwanu; ndipo
kuchokera Kubweya wake
wautaliutali Ndi bweya bwake bwa
manyunyu (Ung'onoung'ono), ndi
tsitsi lake (Laziwetozo,)
mumakonza ziwiya (Zovala)
zosangalatsa, kwa kanthawi.
81. Ndipo mwa zina zomwe
Mulungu Adapanga,
adakupangirani zodzetsa Mthunzi;
ndipo adakupangirani Mokhala
kumapiri (monga mapanga
Akuluakulu). Adakupangiraninso
9 &$&jft£$Je&
Kf ' *t~ 9 ^< 9 ^'tl \ "* i \*
Surat 16. Al-Nahl Juzu 14
572
M tfr\
\ *\ JjnJl 5jj--
Nsalu (zathonje ndi ubweya)
Zokutetezani kukutentha (ndi
kuzizira), Ndiponso
(adakupangirani) zovala
(Zachitsulo) zokutetezani
pankhondo Zanu. Umo ndi
momwe Akukukwaniritsirani
chisomo Chake Kuti mugonjere
(lye).
82. Koma ngati anyoza, basi
palibe Udindo wina pa iwe koma
kufikitsa Uthenga womveka
(popanda kubisapo Kalikonse).
83. Akuchidziwa chisomo cha
Mulungu; Koma akuchikana,
ndipo ambiri A iwo
ngosakhulupirira.
84. Ndipo (akumbutse za) tsiku
lomwe Tidzautsa mboni
mumtundu uliwonse; Kenako
sikudzaloledwa, kwa amene
Sadakhulupirire, (kupereka
madandaulo) Ndipo iwo
sadzauzidwa kuti afunefune
Chiyanjo cha Mulungu (Koma
chilango basi).
85. Ndipo amene achita zoipa
Akadzachiona chilango
(ndikuyamba Kudandaula ndi
kulira), Sichidzachepetsedwa kwa
iwo (chilangocho), Ndipo
sadzapatsidwa mwayi wina.
86. Ndipo amene
ankam'phatikiza Mulungu
Akadzawaona aphatikizi awowo
®&&$tt&&
Surat 16. Al-Nahl Juzu 14
573 ht >&
\ *\ Jj*Ji 3jj--
Adzati: "Mbuye wathu! Awa ndi
Aphatikizi athu omwe tidali
Kuwapembedza m'malo mwa
Inu." Ndipo (aphatikizi wo
akadzamva mawu awa)
Adzawaponyera mawu awo
(nkunena Kuti): "Ndithu, inu ndi
abodza."
87. Tsiku limenero onse
adzadzitula kwa Mulungu; ndipo
zidzawataikira zomwe Adali
kuzipeka.
88. Tsono amene
sadakhulupirire ndi Kumaletsa
anthu kunjira ya Mulungu
Tidzawaonjezera chilango
Pamwamba pa chilango chifukwa
Chakuononga kwawo.
89. Ndipo (akumbutse za) tsiku
lomwe Tidzautsa mboni
mumtundu uliwonse Zochokera
mwa iwo omwe adzawachitira
Umboni (pa zomwe zinkachitika
ndi Iwo;) ndipo tidzakubweretsa
iwe Kukhala mboni pa awa (anthu
ako;) Ndiponso takuvumbulutsira
Buku ili Lomwe likufotokoza za
chinthu chilichonse Lomwenso ndi
chiongoko ndi mtendere Ndiponso
ndi nkhani yosangalatsa Kwa
ogonjera (Mulungu).
90. Ndithudi, Mulungu
akulamula (Kuchita) chilungamo,
ndikuchita Zabwino, ndi kupatsa
achinansi, Ndipo akuletsa zauve
fa' 9 f 99
&*ii*J>J
).* \f 9 < *\ \'» ' 9 }*< 9 *
Surat 16. Al-Nahl Juzu 14
574
M *>!
\ 1 J~Jl i>y*
ndi zoipa Ndi kupyola malire;
akukulangizani Kuti muzindikire
ndi kukumbukira.
91. Ndipo kwaniritsani lonjezo
(limene Mukupereka mdzina) la
Mulungu pamene Mulonjeza,
ndipo musaswe malonjezowo
Pambuyo pakuwalimbikitsa;
pomwe Mwasankha Mulungu
kukhala mboni Yanu; ndithu,
Mulungu akudziwa. (Zonse)
zimene mukuchita.
92. Ndipo musakhale monga
mkazi yemwe Adakhulula ulusi
wake pambuyo Pouluka
mwamphamvu, mukukuchita
Kulumbira kwanu pakati panu
kukhala Kwa chinyengo, chifukwa
chakuti gulu La mtundu wina
nlochuluka kwambiri Kuposa gulu
la mtundu wina (powasiya Omwe
mudalonjezana nawo chifukwa
Chakuwaona kuchepa, ndi
kukagwirizana ndi Omwe
simudalonjezane nawo chifukwa
Chakuwaona kuchuluka); Ndithu,
Mulungu akukuyesani mayeso
Panjira yotere; ndipo ndithu
patsiku la Kiyama
adzakufotokozerani za Zomwe
mudali kusiyana.
93. Ndipo Mulungu akadafuna,
ndithu, Akadakuchitani kukhala
gulu limodzi, (Nonsenu
mukadamumvera monga Momwe
Surat 16. AI-Nahl Juzu 14
575 hi *>'
S 1 J^Ji *^
adawachitira Angelo, koma
Adakupatsani ufulu kuti muchite
Chimene mufuna); komatu
amamulekerera Kusokera amene
wamfuna, ndipo Amamuongola
wamfuna; ndipo, ndithu
Mudzafunsidwa pa zomwe
munkachita.
94. Ndipo musakuchite
kulumbira kwanu kukhala Njira
yonyengererana pakati panu
Kuopera kuti mwendo ungaterere
(Panjira yolungama nkukagwera
ku moto) Pambuyo pokhazikika
mwendowo (Panjirapo) ndi
kukazilawa zoipa Chifukwa
chakutsekereza kwanu (anthu)
Kunjira ya Mulungu, ndipo
nkupeza Chilango chachikulu
(tsiku lachimaliziro).
95. Ndipo musagulitse
mapangano a Mulungu ndi mtengo
wochepa (Wa zomwe mukupeza
pano padziko Lapansi). Chimene
chili kwa Mulungu, ndicho
chabwino kwa inu Ngati
mukudziwa.
96. Zomwe mulinazo nzakutha
ndipo Zili kwa Mulungu ndizo
zosatha Ndithudi Ife tidzawapatsa
malipiro (Aakulu zedi) amene
adapirira Oposera zabwino zimene
ankachita.
97. Amene akuchita zabwino,
wamwamuna Kapena wamkazi
©^;8i*£#£SS*g
Surat 16. Al-Nahl Juzu 14
576 h * *>»
\ n j*di 5j^
uku ali Msilamu Timkhazika ndi
moyo wabwino (pano Padziko, ndi
tsiku la Kiyama) Tidzawalipira
malipiro awo mochuluka
Kwambiri chifukwa cha zabwino
zomwe Ankachita.
98. Ndipo ukafuna kuwerenga
Qur'an Dzitchinjirize ndi Mulungu
kwa Satana wopirikitsidwa
(ponena kuti Awudhu Billahi mina
Shaitwani Rajim).
99. Ndithu, iye (satana) alibe
mphamvu pa amene
Akhulupirira ndi kutsamira Kwa
Mbuye wawo.
100. Ndithudi mphamvu zake
zili pa amene Akumusankha
(am'lola) Kukhala bwenzi lawo
(Mlangizi wawo) ndiponso ndi
omwe Akumphatikiza iye (ndi
Mulungu).
101. Ndipo tikasintha aya
ndikubwera ndi Ina pamalopo,
pomwe Mulungu akudziwa
Zimene akuvumbulutsa, akunena:
"Ndithu, iwe ndiwe wopeka."
Koma ambiri aiwo sadziwa
(chilichonse).
102. Nena: "Mzimu woyera
(Gabriel) waitsitsa (Qur'an)
kuchokera kwa Mbuye wako
Mwachoonadi kuti awalimbikitse
Nayo amene akhulupirira ndi kuti
Ikhale chiongoko ndi nkhani
Yabwino kwa amene alowa
®
'9 V &
Sural 16. Al-Nahl Juzu 14
577 1 t *>«
^ "V J»iJl Oj^-.
m'Chisilamu (Amene agonjera
Mulungu).
103, Ndithu, tikudziwa kuti iwo
akunena: "Pali munthu amene
akumphunzitsa." (Koma)
chiyankhulo cha amene
Akumganizirayo nchachilendo,
Ndipo ichi (chiyankhulo cha
Qur'an) Ndi chiyankhulo cha
Chiarabu chomveka.
104, Ndithudi amene
sakhulupirira aya Za Mulungu,
Mulungu sawaongolera (Kunjira
ya choonadi), choncho Adzapeza
chilango chowawa.
105, Ndithudi amene
sakhulupirira Aya za Mulungu ndi
amene Amapeka bodza (ndi
kumalifalitsa Kwa anthu) ndipo
iwowo ndiwo onama.
106, Amene akukana Mulungu,
pambuyo Pomkhulupirira,
(chilango Chachikulu
chikumyembekezera), Kupatula
yemwe adakakamizidwa, Uku
mtima wake utakhazikika pa
Chikhulupiriro; koma amene
Akutsekulira mtima wake
Kusakhulupirira, mkwiyo wa
Mulungu uli Pa iwo (ndipo anthu
otere) adzapata Chilango
chachikulu. 1
1 Omasulira Qur'an akunena kuti ndime iyi idatsika chifukwa cha Ammar Bun
Yasir. Amushirikina adamgwira ndi kumuvutitsa zedi kufikira iye adawapatsa
chomwe iwo ankafuna kwa iye monkakamiza kutero. Anthu adati: "Ndithudi,
Surat 16. Al-Nahl Juzu 14
578 hi *>»
S 1 J*di l^
107. Zimenezo nchifukwa
chakuti iwo Adakonda moyo
wadziko lapansi Kwambiri kuposa
wa pambuyo Pa imfa; ndi kutinso
Mulungu saongola Anthu
osakhulupirira.
108. Iwo ndi omwe Mulungu
adawadinda M'mitima mwawo,
m'makutu mwawo, Ndi m'maso
mwawo (chifiikwa cha Kusimbwa
kwawo). Ndipo iwo
Ngonyalanyaza (malamulo A
Mulungu) kwambiri.
109. Palibe chikaiko chakuti
iwo ngotaika Kwambiri pa tsiku la
chimaliziro.
110. Ndithudi kenako Mbuye
wako, Kwa amene adasamuka
pambuyo Pakusautsidwa (kufikira
adanena Zosayenera) komanso
nkuchita jihad Ndikupirira
(chifukwa cha "dini",) ndithu,
Mbuye wako pambuyo
pazimenezo, Ngokhululuka
kwambiri, Ngwachisoni.
111. (Akumbutse za) tsiku
lomwe mzimu Uliwonse udzadza
ukudziteteza wokha (Wosalabadira
za mwana wake, mkazi Wake ndi
©t^l^i
**tt
Ammar watuluka m'Chisilamu." Mtumiki (SAW). Adati: "Ndithudi, Ammar
ngodzaza ndi chikhulupiriro kuyambira kumutu mpaka kumapazi. Chikhulupiriro
chasakanikirana ndi minofu ndi magazi ake".
Zitatero Ammar adabwera kwa Mtumiki (SAW) uku akulira. Mtumiki (SAW)
adati kwa iye: "Kodi ukupeza bwanji mtima wako?" lye adati: "Ngokhazikika pa
chikhulupiriro." Mtumiki adati: "Ngati abwereranso iwenso bwerezanso zimene
wanenazo."
Surat 16. AI-Nahl Juzu 14
579 > i *>»
\ >\ J*Ji Sjj-
abale ake,) ndipo mzimu Uliwonse
udzalipidwa molingana ndi
Zochita zake zimene unkachita,
Ndipo iwo sadzachitidwa
chinyengo (Pochepetsedwa
mphoto yawo yoti Alandire.)
112. Ndipo Mulungu waponya
fanizo Lamudzi womwe udakhala
mwa Mtendere, mokhazikika
"riziki" Lake (madalitso)
linkaudzera Mochuluka kuchokera
malo aliwonse; Koma (mudziwo)
udakana mtendere Wa Mulungu
(pakusathokoza); Choncho
Mulungu adaulawitsa Chovala cha
njala ndi mantha Chifukwa cha
(zoipa) zomwe (anthu Ake) adali
kuchita.
113. Ndipo adawadzera
mtumiki wochokera Mwa iwo,
koma adamtsutsa; choncho
Chilango chidawafika uku ali
Odzichitira okha zoipa.
114. Idyani zimene Mulungu
wakupatsani Zomwe zili zahalali,
zabwino; ndipo Yamikani
mtendere wa Mulungu Ngatidi
mukupembedza lye.
115. Ndithu, wakuletsani
(kudya) zakufa Zokha, magazi
(liwende), nyama ya Nkhumba ndi
chimene chazingidwa Posatchula
dzina la Mulungu. Koma amene
wasimidwa (Nadya choletsedwa)
Mosafuna kapena kupyoza
®fci
'*§&
Surat 16. Al-Nahl Juzu 14
580
U *>i
^ n Jj*J» 5jj--
Muyeso, (Mulungu amkhululukira)
Ndithudi Mulungu Ngokhululuka
kwabasi, Ngwachisoni.
116. Ndipo musanene chifukwa
chabodza Lomwe malirime anu
akunena (kuti) "Ichi nchololedwa;
ichi ncholetsedwa; (Popanda
umboni)." Kuopera Kuti
mungampekere bodza Mulungu.
Ndithu, amene akupekera bodza
Mulungu, sangapambane.
117. Ndichisangalalo chochepa
(cha M'dziko lapansi chimene
chikuwachititsa Zimenezo); ndipo
iwo Adzapata chilango chowawa.
118. Ndipo kwa Ayuda
tidawaletsa kale Zimene
takusimbira. Ndipo sitidawachitire
Chinyengo (pakuwaletsa
zimenezo), Koma iwo okha adali
kudzichitira Chinyengo.
119. Kenako ndithu, Mbuye
wako, kwa Amene achita zoipa
mwaumbuli ndipo Nkulapa
pambuyo pazimenezo nachita
Zabwino, ndithudi Mbuye wako
Pambuyo pazimenezo
Ngokhululuka kwabasi,
Ngwachisoni.
120. Ndithu, Ibrahim adali
mtsogoleri; (Chitsanzo chabwino
kwa anthu), Womvera Mulungu,
wopendekera Kuchoonadi ndipo
sadali mwa Omphatikiza
(Mulungu ndi mafano).
Surat 16. Al-Nahl Juzu 14
581
U *>»
\ n >Ji 5j^
121. (Adali) wothokoza
mtendere Wake (Mulungu);
Adamsankha ndipo
Adamuongolera kunjira yolunjika.
122. Ndipo tidampatsa zabwino
padziko Lapansi, ndipo ndithudi,
iye Patsiku la chimaliziro
adzakhala M'gulu la anthu abwino.
123. Kenako takudziwitsa (iwe
Muhammad{SAW}) Kuti: "Tsatira
njira (chipembedzo) Ya Ibrahim
(yemwe adali) wokwanira
Mkulungama, ndipo sadali mwa
Omphatikiza (Mulungu ndi
mafano.)
124. Ndithudi Sabata idaikidwa
kwa amene Adatsutsana pa za iyo
(Sabatayo); ndithu, Mbuye wako
adzaweruza pakati pawo Tsiku la
Kiyama pazomwe Adali kusiyana.
125. Itanira (anthu) kunjira ya
Mbuye Wako mwanzeru ndi
ulaliki wabwino; Ndipo tsutsana
nawo mkutsutsana Kwabwino
(osati motukwanana kapena
Monyozana). Ndithu, Mbuye wako
Iye Ngodziwa kwambiri za amene
asokera Kunjira Yake, ndiponso
Iye Ngodziwa Kwambiri za amene
aongoka.
126. Ndipo ngati mukubwezera
(choipa chimene Mwachitiridwa),
bwezerani cholingana ndi Chimene
mwachitiridwacho koma ngati
JlUiS^ftjSKB
>lfi$
Surat 16. Al-Nahl Juzu 14
582
\t *><
\ \ J~Ji Sj^,
Mutapitirira (posiya kubwezera),
ndithu, Kutero ndi ubwino kwa
opirira.
127. Ndipo pirira. Kupirira
kwakoko Kusakhale pachina chake
koma Mulungu Basi. Ndipo
usadandaule chifukwa cha Iwo,
(iwo akudzisokeretsa okha). Ndipo
Usakhale wobanika chifukwa cha
chiwembu Chomwe akuchita.
128. Ndithu, Mulungu ali
pamodzi Ndi amene akumuopa ndi
Amenenso akuchita zabwino.
Surat 17. Al-Isra'
Juzu 15
583
>0 frjJH
> v t\j*y\ oj^-
Sura iyi ili ndi aya 111; idavumbulutsidwa ku Makka,
kupatula aya 26, 32, 57 ndi aya zonse kuyambira 73 mpaka 80;
zonsezi zidavumbulutsidwa ku Madina.
Sura iyi yayamba ndikulemekeza Mulungu ndipo kenako
yatchula nkhani ya Isra'a ndipo yatchulanso za uthenga wa Musa
ndi zomwe zidachitika ndi ana a Isiraeli.
Kenako surayi yafotokozanso za ulemerero wa Qur'an
posonyeza anthu njira yolunjika. Ndipo yafotokozanso
zisonyezo za Mulungu za chilengedwe zomwe zikupezeka mu
usiku ndi mu usana. Yafotokozanso za mphoto yomwe anthu
akalandire pa tsiku la chimaliziro molingana ndi zomwe
adatsogoza kuchita padziko lapansi.
Mulungu m'surayi wafotokozanso zomwe zimachititsa kuti
mitundu ya anthu ionongeke, ndi khalidwe la munthu aliyense
payekha, ndi zotsatira zantchito pa tsiku la chiweruzo. Ndipo
padzanso mawu olimbikitsa kuchitira makolo zabwino, ndi
mom we anthu angachitire ndi chuma chawo.
Kenako msurayi mwadza malangizo khumi omwe ngofunika
pa mtundu wa munthu. Ndipo Mulungu wakana bodza la
opembedza mafano pa nkhani yokhudza angelo yomwe
amawanamizira nayo.
Surat 17. Al-Isra' Juzu 15
584
\e> frjJUi
\ V t\j*y\ *;>*»
Surat Al-Isra' XVII
\ ljm& k
fl
M'dzina la Mulungu waChifundo
Chambiri, waChisoni.
1. Ulemerero ngwa Yemwe
adayendetsa kapolo Wake usiku
(umodzi) kuchokera Mu Msikiti
Wopatulika (wa Makka) Kupita ku
Msikiti wakutali (wa Baitul-
Muqaddas), womwe tidaudalitsa
ndi Kuzidalitsa zam'mphepete
mwake; (Tidampititsa kumeneko)
kuti timsonyeze Zina mwa
zisonyezo Zathu; ndithu, lye
(Mulungu) Ngwakumva ,
Ngowona ( chilichonse). 1
2. Ndipo Musa tidampatsa Buku
(la Taurat) Tidaliika kukhala
chiongoko kwa Ana a Isiraeli
(Mulungu adawauza):
"Musadzipangire atetezi kusiya
Ine."
3. (Ndiponso adawauza kuti, E,
inu eni) Mbumba ya amene
tidawasenza pamodzi Ndi Nuhi!
(Khalani othokoza monga Tate
wanu.) Ndithu, iye adali Kapolo
wothokoza kwambiri.
4. Ndipo tidawazindikiritsa ana
a Isiraeli m'Bukulo, kuti: "Ndithu,
ojt^\i^3^j
. j_iiT
^&C£&fy$&j
1 Mneneri Muhammad (SAW) pamene adakwezedwa kumwamba adaona
zisonyezo zikuluzikulu za Mulungu monga Munda wamtendere, moto, mtengo
wotchedwa Sidrat Muntaha, Angelo, Aneneri ndi zina zododometsa.
Surat 17. Al-Isra' Juzu 15
585
>a fr jju»
\ V t\j*y\ ojj^
Inu muononga padziko kawiri,
ndipo Mudzapyola malire pochita
zoipa, Kupyola malire kwakukulu.
5. Ndipo likadzafika lonjezo
(lakupatsidwa Chilango
chakuononga) koyamba
mkuononga Kuwiriko,
tidzawakhwirizira pa inu anthu,
Athu eni kumenya nkhondo
mwaukali, Adzakhala
akuzungulira mkatikati
Mwanyumba zanu ndipo Lidali
lonjezo lochitika.
6. Kenako tidakubwezerani
kupambana pa iwo (Omwe
adakugonjetsani poyamba); ndipo
Tidakupatsani chuma ndi ana,
Ndikukudalitsani kukhala ndi gulu
Lochuluka.
7. (Tidati kwa iwo), ngati
muchita bwino (Pomumvera
Mulungu), ubwino ngwanu
(Padziko lapansi ndi patsiku la
Chimaliziro);ngati muipitsa
(ponyoza Mulungu), kuipako kuli
pa inu nokha. Choncho pamene
idadza nthawi ya Lonjezo
lachilango chomaliza,
(Tidakutumizirani adani anu) kuti
apereke Kunyozeka pankhope
zanu, ndikutinso alowe Munsikiti
monga adalowera mnthawi
yoyamba, Ndikuti aononge
chilichonse chimene Achigonjetsa;
kuononga kwakukulu.
^;<^u»3ki&js
<&Z2\&;^%
o* *£_ K'Xl *H '"\ *& ?'"i*\
Surat 17. Al-Isra' Juzu 15
586 ^ * *>»
^ v t\j*y\ *jj~>
8. (Koma ngati mudzalungama
mzochita zanu), Mbuye wanu
adzakuchitirani Chifundo; ndipo
ngati mudzabwereranso
(Kumachitidwe anu okhota),
tidzabwereranso (Kukulangani);
ndipo taikonza Jahannama
Kukhala ndende ya osakhulupirira.
9. Ndithu, iyi Qur'an
ikuongolera ku njira Yoongoka ndi
kuuza okhulupirira nkhani
Zabwino omwe akuchita zabwino,
kuti Iwo adzalandira malipiro
aakulu (Patsiku la chiweruzo);
10. Ndiponso ikuuza
omwe sadakhulupirire Za tsiku
lachimaliziro kuti Tawakonzera
chilango chowawa.
11. Ndipo munthu amafulumira
kupempha zoipa Monga
momwenso amafulumirira
kupempha Zabwino; ndithu,
munthu ngwaphuma (Mzochita
zake).
12. Ndipo tapanga usiku ndi
usana (mkusinthana-Sinthana
kwake) monga zisonyezo Ziwiri
(zosonyeza umodzi wa Mulungu
Ndi mphamvu Zake zoposa);
ndipo Tidachifafaniza chisonyezo
cha usiku (Kuti chisakhale ndi
kuunika) ndipo Chisonyezo cha
usana tidachipanga Kuti chikhale
ndikuunika; kuti Mufunefune
Surat 17. Al-Isra' Juzu 15
587
>0 frj*-l
\ V t\j*y\ 5j>-
ubwino wochokera kwa Mbuye
wanu, ndikuti mudziwe
chiwerengero Cha zaka
ndichiwerengero (cha miyezi Ndi
masiku); ndipo chinthu chilichonse
(Chofunika pachipembedzo ndi
zam'dziko), Tachilongosola
bwinobwino, Mwatsatanetsatane.
13. Ndipo munthu Aliyense
tammangirira Mkhosi zochita
zake; ndipo tsiku La kiyama
tidzamtulutsira kaundula (Momwe
muli zochita zake); Adzampeza
wovundukulidwa.
14. (Kudzanenedwa kwa iye:)
"Werenga Kaundula wako
(kupyolera m'mphamvu za
Mulungu ngakhale padziko lapansi
Siunkatha kuwerenga); mzimu
wako Ukwanira lero
kudzi werengera. "
15. Amene waongoka (potsatira
njira ya Choonadi), wadzipindulira
yekha Ndipo amene wapotoka (ku
njira ya Choonadi), wadzitaya iye
mwini Ndipo msenzi wosenza
machimo sadzasenza Mtolo
wamachimo awina. Ndipo Ife
Siolanga (zolengedwa) kufikira
titatumiza Mtumiki (kuti
azidziwitse choonadi. Zikakana
ndipomwe timazilanga).
16. Ndipo tikafuna kuononga
mudzi (pamene eni Mudziwo
®s^&&#vP$$s\
^jX^Cj^'3 %'>)%
Surat 17. AMsra' Juzu 15 I 588 > d *j*r\
\ v t\j*y\ Sjj-
akuchita zoipa), timawalamula
Opeza bwino a m'menemo (kuti
asiye Zoipa). Koma akapitiriza
kuononga Kwawo m'menemo,apo
ndipo liwu (Lakuwaononga)
limatsimikizidwa pa Iwo ndipo
timauononga, kuononga
Kwakukulu.
17. Ndi mibadwo yochuluka
imene tidaiononga Pambuyo pa
Nuhi! Ndipo akukwanira Mbuye
wako kudziwa bwinobwino ndi
kuona Bwinobwino uchimo wa
akapolo ake. (Palibe chobisika kwa
lye M'zochita chita za anthu).
18. Amene afuna zosangalatsa
za m'dziko Zachangu
(ndikumaikirapo mtima pa izo,)
Timpatsiratu mwachangu padziko
Lapansi chimene tikufuna Kwa
amene tafuna (kumpatsa;) koma
(tsiku Lachimaliziro) tamkonzera
Jahannama Adzailowa ali
wonyozeka, wopirikitsidwa Apa
ndi apo.
19. Ndipo amene afuna Tsiku
lachimaliziro (Mzochita zake)
ndikuligwirira Ntchito yake
yeniyeni uku Ali msilamu, iwowo
Khama lawo lidzakhala
lolandiridwa.
20. Onse awa, (abwino ndi
oipa), timawapatsa Awa ndi awa
mwazopatsa za Mbuye wako;
dssQs3x^%$4$i
Surat 17. Al-Isra'
Juzu 15
589
>0 frj*-!
> V t\j*f\ 5j>-
Ndipo zopatsa za Mbuye Wako
sizotsekerezedwa (Kuti zisamfike
kapolo Wake).
21. Taona (ndi diso lolingalira)
m'mene Tawasiyanitsira mkupeza
bwino, ena nkukhala Pamwamba
pa anzawo (pachuma ndi pamoyo
Wangwiro); ndipo pa tsiku la
chimaliziro Kusiyana kwawo pa
masitepe ndi ulemerero,
Nkwakukulu kwabasi.
22. Usadzipangire mulungu
wina ndi kumphatika Kwa
Mulungu; kuti ungadzakhale
wodzudzulidwa (Kwa Mulungu)
ndikusiidwa wopanda m'thandizi.
23. Ndipo walamula Mbuye
wako kuti musapembedze (Wina)
koma lye yekha, ndi kuti Muchitire
zabwino makolo (anu). Ngati
M'modzi waiwo afika msinkhu
waukalamba Uli naye, kapena
onse awiri, Usawanenere,mawu
amnyozo Ndiponso Usawakalipire
koma yankhula nawo Ndi mau
aulemu. 1
24. Ndipo afungatire ndi phiko
lodzichepetsa Powachitira chisoni,
$0S&$SM^J*£
M'ndimeyi Mulungu akulamula anthu Ake kuti apembedze lye yekha;
asapembedze china chake cholengedwa monga miyala, mitengo, dzuwa,
mwezi, nkhalango zowirira, mizimu ya anthu akufa ndi ziwanda. Koma
chikhulupiriro chathu chikhale mwa Mulungu yekha. Tikafuna kudziteteza
tidziteteze ndi Mulungu. Ndiponso Mulungu watilamula kuchitira zabwino
makolo. Tisawanenere mawu amwano ndiponso tisawakalipire. Koma
tiwanenere mau aulemu.
Surat 17. Al-Isra' Juzu 15
590
>0 ij±\
1 V *lj^1 5jj--
ndipo nena: "Mbuye Wanga
achitireni chisoni (makolo anga)
Monga momwe ankandilerera ku
ubwana."
25. Mbuye wanu akudziwa
kwambiri zomwe zili M'maganizo
mwanu; ngati muli ofuna Kuchita
zabwino, (kwa makolo anu lye
Akudziwa. Ndipo ngati
mutawalakwira, Kenako
ndikulapa), ndithu, lye ndi Mwini
kukhululukira otembenukira kwa
lye.
26. Ndipo mnansi wako,
masikini ndi Wapaulendo (yemwe
alibe Choyendera) mpatse gawo
lake (La chuma chako) ndipo
usamwaze (Chuma chako)
mosakaza.
27. Ndithu omwaza chuma
mosakaza, ndi Abale a satana
(otsatira satana), Ndipo satana
ngosathokoza Kwa Mbuye wake.
28. Ndipo ngati ukuwapewa
opempha (Pamene ulibe
chowapatsa) pamene Ukufunafuna
chifundo cha Mbuye Wako
chomwe ukuchiyembekezera, nena
Kwa iwo mau ofewa (ponena kuti:
"Ndikapeza chokupatsani,
ndikuninkhani.")
29. Ndipo mkono wako
usaukhalitse Ngati kuti
wamangidwa kukhosi kwako,
*&&$%&$
^JflSi-^MK
Surat 17. AI-Isra' Juzu 15
591 > * *>»
>v *\j*y\ 5jj--
Ndiponso usautambasule
mosayenera, Ungadzakhale
wodzudzulidwa ndiwosowa. 1
30. Ndithu, Mbuye wako
amamtambasulira Riziki amene
wamfuna, ndikulichepetsa (Kwa
amene wamfuna). Ndithu, lye
Ngodziwa bwino; wopenya bwino
za Akapolo Ake.
31. Ndipo musaphe ana anu
poopa umphawi. Ife ndi amene
tikuwapatsa iwo ndi Inu. Ndithu,
kupha anawo ndi Tchimo lalikulu.
32. Ndipo musachiyandikire
chiwerewere; Ndithu, (icho) ndi
uve (chonyansa chachikulu),
Ndiponso ndi njira yoipa.
33. Ndipo musaphe munthu
amene Mulungu waletsa
(Kumupha) koma mwachoonadi
(Poweruza oweruza zakuphedwa
ngati Utam'gwera mulandu
woyenera kuphedwa). Ndipo
amene waphedwa mopanda
chilungamo, Tapereka mphamvu
kwa mlowammalo wake (Wa
wophedwayo atafuna
angamuphenso Kapena kumsiya
ndikulandirapo dipo); Koma
asapyole malire mukuphako.
4$tt&&^3tifty^'
^ T7 ^
1 Tanthauzo la ndime iyi nkuti mkono wako usakhale wofumbata posiya
kugawira ena zomwe ulinazo; ndikutinso usatambasule popatsa mosakaza
koma kuchita zapakatikati; osachita umbombo ndiponso osasakaza. Anthu
aumbombo ndi osakaza chuma, ndi abale a satana.
Surat 17. Al-Isra'
Juzu 15
592
^a *>i
\ V $\jJ$\ oj^-
Ndithu, lye ngothandizidwa ndi
Shariya.
34. Ndipo musachiyandikire
chuma cha wamasiye (Pochidya
mosayenera) koma pokhapokha
M'njira yomwe ili yabwino,
kufikira Anawo atakula, (apo tsono
apatsidwe Chuma chawocho);
ndipo kwaniritsani Lonjezo,
popeza lonjezo lidzafunsidwa
(Tsiku la Kiyama).
35. Ndipo kwaniritsani mlingo
pamene Mulinga, ndipo yesani ndi
sikelo Zabwino, zimenezo ndi
zabwino (kwa inu) Ndiponso
mathero (ake) ngabwino.
36. Ndipo usazitsate (pongo
Ziyankhulayankhula Kapena
kuzichita) zomwe Sukuzidziwa;
ndithu Makutu, maso Ndi mtima
zonsezo Zidzafunsidwa.
37. Ndipo usayende padziko
modzitukumula; Ndithu, iwe
sungang'ambe nthaka Ndiponso
sungalifikire phiri M'kutalika.
38. Zonsezi kuipa kwake
Nkonyansidwa kwa Mbuye wako.
39. Izi ndi zina mwa za nzeru
zomwe Mbuye wako
wakuvumbulutsira. Usakhale Ndi
mulungu wina ndi kumphatikiza
Kwa Mulungu, kuti
ungadzaponyedwe ku Jahannama
Siirat 17. Al-Isra' Juzu 15 I 593 I \ o ^\ w t\j*y\ 5^
uli wodzudzulidwa ndi
Wopirikitsidwa apa ndi apo.
40. Kodi Mbuye wanu
wakusankhirani ana Aamuna,
ndipo mwini wadzipangira Ana
aakazi achingelo? Ndithu, Inu
mukunena liwu lalikulu.
41. Ndipo ndithu, talongosola
lamulo la chinthu Chilichonse
mwatsatanetsatane m'Qur'an Iyi
kuti akumbukire, ndipo (oipa)
Siikuwaonjezera (china) koma
Kuida ndi kuithawa.
42. Nena: "Pakadakhala
milungu ina pamodzi Ndi
Mulungu, monga momwe
akunenera, Ikadafuna njira
yomufikira (Mbuye) Mwini
mpando wa chifumu (ndi Kumthira
nkhondo)".
43. Wayera ndipo watukuka
Mulungu ku zimene akunenazo;
Kutukuka kwakukulu (kwabasi).
44. Zonse zakumitambo isanu
ndi iwiri Ndi nthaka ndi
zam'menemo, Zikulemekeza lye;
ndipo palibe Chilichonse koma
chikumlememekeza ndi
Kumtamanda; koma inu
simuzindikira Kulemekeza
kwawo! Ndithujye (Mulungu)
Ngodekha, Ngokhululuka.
45. Ndipo ukamawerenga
Qur'an (zikukhala Ngati) taika
$££&
m
{^^^£>^2^Q\j^\^^\^
Surat 17. Al-Isra' Juzu 15
594
> o ftjA-i > V fri^i 5jj-
chotchinga Pakati pako ndi pakati
pa amene Sadakhulupirire za tsiku
lachimaliziro.
46. Ndipo (ngati) taika
zitsekerero M'mitima mwawo kuti
angaizindikire, Ndipo (ngati)
mmakutu mwawo muli Kulemera
kwa ugonthi. Ndiponso
ukamtchula M'Qur'an Mbuye wako
yekha, iwo Akutembenuka ndi
misana yawo moipidwa.
47. Ife tikudziwa chifukwa
chomwe akuimvetsera (Qur'an),
pamene akukumvetsera Ndi
pamene akunong'onezana, awo
Achinyengo, (ndikuuza Asilamu
kuti) "Inu simutsatira (wina) koma
munthu Wolodzedwa."
48. Ona momwe akukufanizira
ndi Mafanizo abodza. (Nthawi zina
akuti Ndiwe wolodzedwa, nthawi
zina akuti Ndiwe mfiti!) choncho
asokera, Ndipo sangathe kupeza
njira (Yeniyeni).
49. Ndipo akunena: "Kodi
tikadzakhala mafupa Odukaduka,
tidzaukitsidwanso Kukhala
zolengedwa zatsopano?"
50. Nena: "Khalani miyala
kapena Zitsulo,
51. Kapena cholengedwa
chilichonse Mwazomwe zikuoneka
kuti nzovuta Kwambiri m'mitima
mwanu (m'maganizo Mwanu),
^m>%*w&
®l
Surat 17. AMsra' Juzu 15
595 p**j*-»
> V *ij-»)h 5j>-
(ngakhale mutakhala zimenezo,
Mudzaukitsidwa)" pamenepo
anena: "Ndani adzatibweza?"
Nena: "Yemwe adakulengani
pachiyambi" Pamenepo
adzakupukusira mitu yawo
Ndikunena: "Zichitika liti
Zimenezo?" Nena: "Mwina zili
pafupi!"
52. "(Zidzakhala) pa tsiku
lomwe Adzakuitanani (Mulungu),
ndipo inu Mudzayankha
momuyamikira, ndipo
Mudzaganizira kuti simudakhale
(Padziko lapansi) koma (kwa)
nthawi Yochepa."
53. Ndipo auze akapolo Anga
kuti (Nthawi zonse) azinena
zomwe zili Zabwino; chifukwa
satana Amakhwirizira mikangano
pakati Pawo; ndithu, satana kwa
munthu, Ndi mdani woonekera.
54. Mbuye wanu akukudziwani
bwino. Ngati afuna akuchitirani
chisoni (Mukatembenukira kwa
lye), ndipo Ngati afuna,
akulangani (Mukapitiriza
kumnyoza); ndipo Sitidakutumize
kuti ukhale kapitawo Wawo.
55. Ndipo Mbuye wako
Akuwadziwa bwino Onse ali
kumwamba ndi pansi, Ndithu,
tawapatsa ulemerero Wambiri
aneneri ena kuposa ena. Ndipo
Daud tidampatsa Zaburi.
Siirat 17. Al-Isra' Juzu 15
596
>0 tjJUl
\ V s.\jJ)\ 3jj-
56. Nena: " Aitaneni amene
munkawatcha Kuti ndi mulungu
kusiya lye (Mulungu) Kuti
akuchotsereni Masautso sadzatha
kukuchotserani Vuto lililonse
ngakhale kulisintha (Kuti likhale
chabwino)."
57. Iwo amene akuwapempha
(naonso) Akufunafuna njira
yoziyandikitsira Kwa Mbuye
wawo (ngakhale) omwe Ali pafupi
mwa iwo (ndi Mulungu, Monga
angelo); naonso akuyembekezera
Chifundo Chake ndi kuopa
chilango Chake; ndithu, chilango
cha Mbuye wako, nchoopedwa.
58. Ndipo sipadzapezeka mudzi
uliwonse Koma Ife tidzauphwasula
tsiku la Kiyama lisanadze, kapena
tidzaulanga Ndi chilango chaukali
(ngati uli Woyenerana ndi
zimenezo). Izi Zidalembedwa
m'Buku.
59. Ndipo palibe chimene
chikutiletsa Kutumiza zizizwa
(zomwe Akuzipempha) koma kuti
anthu akale Adazitsutsa. Asamuda
tidawapatsa Ngamira yaikazi kuti
ikhale Chizindikiro choonekera
(chozizwitsa) Koma adaichitira
zosayenera; ndipo Sititumiza
zizizwa ndi cholinga China, koma
kuchenjeza.
60. Ndipo (kumbuka) pamene
tidakuuza Kuti ndithu, Mbuye
^/"*':?'M»'Ii.v4
'**£&
**JL*'
yayw^a^gsts
Surat 17. Al-Isra' Juzu 15
597
^o *jJU|
y v t\j*y\ 5j^
wako wawazungulira Anthu
(mowadziwa bwinobwino;) ndipo
Sitidawachite maloto omwe
tidakuonetsa Koma kuti akhale
mayeso kwa anthu, (Kuti kodi
akhulupirira kapena sakhulupirira,)
Ndiponso (kutchula kwa) mtengo
Wotembereredwa m'Qur'an
(ndimayesonso Kwa iwo;) ndipo
tikuwachenjeza, koma
(Machenjezo athu) sakuwaonjezera
china Koma kulumpha malire
kwakukulu basi.
61. Ndipo (akumbutse) pamene
tidauza Angelo kuti: "Mulambireni
Adam." Ndipo adamulambira
kupatula Iblis (lye) adati:" Kodi
ndimulambire Yemwe mwamlenga
ndi dongo?"
62. Adatinso (kwa Mulungu):
"Kodi Mukuona uyu amene
mwampatsa Ulemerero kuposa
ine? Ngati mundipatsa Nthawi
mpaka tsiku la Kiyama, ndithu
Ndiononga mbumba yake (yonse)
kupatula Ochepa basi."
63. (Mulungu) adati: "Choka!
Amene Adzakutsata mwa iwo,
ndithu, Jahannama ndiyo mphoto
yanu Mphoto yokwanira.
64. Ndipo apusitse amene
ungawathe mwa iwo Ndi liwu
lako; ndipo asonkhanitsire Gulu
lako la nkhondo la okwera
Surat 17. Al-Isra' Juzu 15
598
>0 *j*-|
\ V t\j*y\ Ojj-
Akavalo ndi loyenda ndi miyendo;
Tenga gawo lako pa chuma chawo
ndi ana awo; Ndipo alonjeze
(malonjezo abodza)." Koma satana
salonjeza china koma Chinyengo
basi.
65. "Ndithu, akapolo Anga,
ulibe nyonga Pa iwo." Ndipo
Mbuye wako akukwanira Kukhala
mtetezi (wawo).
66. Mbuye wanu ndi Yemwe
amakuyendetserani Zombo
panyanja kuti munke mufunafuna
Ubwino Wake. Ndithu, lye
Ngwachisoni Kwa inu.
67. Ndipo akakupezani
masautso panyanja, Amasowa
amene mumakhala mukuwa
Pembedza kupatula lye (Mulungu).
Koma akakupulumutsirani
kumtunda, Mukutembenuka ndi
kunyoza Mulungu, Ndithu, munthu
ndi wokana (mtendere Wa
Mulungu sayamika.)
68. Kodi mukudziika
pachitetezo ndi Chilango cha
Mulungu (mukafika Pamtunda)
kuti Mulungu sangakulowetseni
Pansi mbali iliyonse ya Pamtunda,
kapena sangakutumizireni
Chigumula chamchenga (kapena
miyala) Kenako inu simudzapeza
mtetezi (Wokupulumutsani
kuchilangocho)?
ifj^^^f^^C^ &it*&\
$%&k
^"l
^
Siirat 17. Al-Isra' Juzu 15 599 1 ^^
\ V *lj~-?1 dj^
69. Kapena mwadziika
pachitetezo kuti (Mulungu)
sadzakubwezeraninso Mnyanjamo
kachiwiri ndipo
Nkudzakutumizirani chimphepo
chaukali Ndikukumizani chifukwa
cha Kusakhulupirira (ndi
kusathokoza kwanu,) Kenako inu
nkusapeza wokutetezani Kwa Ife?
70. Ndipo ndithu, tawalemekeza
ana a Adam; Ndipo tawapatsa
zokwera pamtunda Ndi panyanja;
tawapatsa zopatsa Zabwino
kwambiri; ndipo tawapatsa
Ulemerero kuposa zambiri
m'zomwe Tidalenga; ulemerero
waukulu Kwabasi.
71. (Akumbutse za) tsiku
lomwe Tidzaitana anthu onse
m'dzina la mneneri Wawo;
choncho, amene Adzapatsidwe
akaundula awo ndi dzanja
Lamanja,iwo adzawerenga
akaundula awowo
(Mwachisangalalo), ndipo
Sadzaponderezedwa ngakhale
pang'ono.
72. Ndipo amene ali wakhungu
pano (padziko Lapansi posapenya
zizindikiro) Adzakhalanso
wakhungu patsiku La chimaliziro,
ndipo adzakhala Wosokera njira
kwambiri (kumeneko).
73. Ndipo ndithu, adatsala
Pang'ono kukusokoneza Pazimene
B»
^3&AJ-^S^S&
Surat 17. Al-Isra'
Juzu 15
600
>0 lj*r\
W ^j*>y\ djj~-
tavumbulutsa kwa iwe kuti
Utipekere zina zake m'malo mwa
izi; Pamenepo, akadakusankha
kukhala bwenzi (Lawo).
74. Ndipo tikadapanda
kukulimbikitsa, Ukadapendekera
kwa iwo, kupendeka Kwapang'ono.
75. Tero, ndithu,
tikadakulawitsa chilango
Chachikulu chamoyo (wapadziko
lapansi) Ndi chilango chachikulu
utafa; Ndipo kenako siukadapeza
mthandizi Wokupulumutsa kwa Ife.
76. Ndipo padatsala pang'ono
kuti Akusowetse mtendere
M'dziko ili (la Makka) kuti
akutulutse M'menemo; koma
pambuyo Pako sakadakhala (ndi
moyo) Kupatula (nthawi) yochepa.
77. Chimenechi ndi
chikhalidwe cha omwe
Tidawatuma patsogolo pako mwa
atumiki Athu, ndipo supeza
kusintha Pachikhalidwe Chathu.
78. Pemphera swala (za Farazi),
dzuwa Likapendeka mpaka
mumdima wausiku (Zomwe ndi
swala za Zuhri, Asri, Maghrib ndi
Isha), ndipo pempheranso Swala
ya Fajir: ndithu swala ya Fajir
amaichitira umboni (angelo).
79. Ndipo pakati pa usiku,
dzuka mtulo Ndi kupemhera
swala; ilo ndipemphero Loonjeza
v\J^X$$ty^<$&_i
Surat 17. Al-Isra' Juzu 15
601
>o t jJU|
W^l *J>-
paiwe, kuti Mbuye Wako
angakuimike pamalo paulemu
Potamandidwa (ndi zolengedwa
zonse Pa tsiku la Kiyama.)
80. Ndipo nena (mawu awa
pomwe ukupemphera): "Mbuye
wanga! Ndilowetseni, kulowetsa
Kwabwino (paliponse pamene
ndikulowa), Ndiponso nditulutseni,
kutulutsa Kwabwino (paliponse
pamene ndikutuluka); Ndipatseni
mphamvu zochokera kwa Inu
Zondithandiza ndi kugonjetsera
adani".
81. Ndipo nena: "Choonadi
chafika, ndipo chachabe
Chachoka; ndithu, chachabe
ndichochoka (Ngakhale patapita
nthawi yaitali)"
82. Ndipo tikuitumiza Qur'an
yomwe Imachiritsa (matenda a
mmitima) Ndiponso ndi chifundo
kwa okhulupirira. Komabe
osalungama siikuwaonjezera
(Kanthu kena) koma kuluza ndi
kutayika.
83. Ndipo tikampatsa chisomo
munthu, (Monga moyo wangwiro
ndikupeza bwino), Amatembenuka
(ndikusiya kutikumbukira
Ndikutipempha), ndipo amadziika
kutali (Ndi Ife chifukwa
chakudzitama ndikudzikuza),
Koma masautso akamkhudza,
*&%££& «5
Siirat 17. Al-Isra' Juzu 15
602
>o *jJU|
w *\j*y\ djj~>
(monga Matenda ndi umphawi)
amataya mtima Kwambiri.
84. Nena (iwe Mneneri, kwa
osakhulupirira A chikuraishi,):
"Aliyense (wa ife ndi Inu) akuchita
ntchito (zake ndikuyenda Panjira
yake) ndipo Mbuye wanu
Ngodziwa kwambiri za yemwe ali
panjira Yolondola (potsatira
choonadi)."
85. Ndipo akukufunsa (iwe,
Muhammad(SAW), Anthu ako
mokhwiriziridwa ndi Ayuda) za
Mzimu. Nena: "Mzimu ndi chinthu
Chomwe akuchidziwa Mbuye
wanga yekha; Ndipo inu
simudapatsidwe nzeru
(Zozindikirira zinthu) koma
pang'ono chabe, (Poyerekeza ndi
nzeru za Mulungu)."
86. Ndipo tikadafuna kufuta
Qur'an (Pachifuwa chako) yomwe
takuvumbulutsira, (Tikadatha
kutero). Kenako sukadapeza kwa
Ife Wokuimirira ndi
kukupulumutsa,
87. Koma (taisiya mu mtima
mwako) chifukwa Cha chifundo
chochokera kwa Mbuye wako;
Ndithu, ubwino Wake pa iwe
ngwaukulu.
88. Nena: "Ngakhale
atasonkhana anthu Ndi ziwanda
(mothandizana) kuti Abwere ndi
%
3^uS>3iSM»
Surat 17. Al-Isra' Juzu 15
603
\0 frjJH
\ v t\j*y\ ojt*
buku longa ili la Qur'an
(Mkayalidwe ka mawu ndi
matanthauzo ake), Sangathe,
ngakhale atathandizana wina Ndi
mnzake".
89. Ndipo ndithu,
tawalongosolera anthu, m'Qur'an
Iyi; mkulongosola kwa njira
Zosiyanasiyana ndikupereka fanizo
Lamtundu uliwonse. Ndipo anthu
ambiri Akukana (zonsezo) koma
kusakhulupirira basi.
90. Ndipo (pamene adalephera
kubwera ndi Qur'an Yawo,) adati:
"Sitingakukhulupirire Mpaka
utatitulutsira kasupe wosaphwa
M'dziko (lathu ili la Makka).
91. Kapena ukhale ndi munda
wazipatso Za kanjedza ndi mphesa
(kuno ku Makka), Ndipo utulutse
mitsinje yambiri pakati Pa
mundapo.
92. Kapena utigwetsere
zidutswa za thambo Pamitu yathu
monga momwe umatiopsezera,
Apo ayi, um'bweretse Mulungu ndi
Angelo (Kuti) tionane nawo
nkhope kwa nkhope
(Mwamasomphenya.)
93. Kapena ukhale ndi nyumba
ya golide, Kapena ukwere
kumwamba. Ndipo
Sitikukhulupirira kukwera kwako
Pokhapokha utabwera ndi buku
Siirat 17. Al-Isra' Juzu 15
604
>o ^\
\ v t\j*y\ ojj-
(lochokera Kwa Mulungu lomwe
likulongosola za kuona Kwako),
kuti tidziliwerenga". Nena (Kwa
iwo): "Mbuye wanga alemekezeke
Ndikupatukana ndi mbiri
zopunguka! Ine sindine kanthu
koma munthu, Mtumiki (monga
aneneri ena) M .
94. Ndipo palibe chimene
(Amshirikina a M'makka)
Chawaletsa kukhulupirira choona
Pamene chivumbulutso
chawadzera, Koma kunena kwawo
(kwa umbuli) kwakuti, "Kodi
Mulungu amatuma munthu
kukhala Mtumiki (Wake)?
95. Nena: "Padziko
pakadakhala angelo
Omayendayenda ndi okhazikika
(m'malo Awo ndi m'nyumba
zawo), tikadawatsitsira M'ngelo
monga mtumiki kuchokera ku
mwamba".
96. Nena: "(Ngati mukutsutsa
uthenga wanga) Mulungu
wakwanira kukhala mboni (ndi
Muweruzi) pakati panga ndi pakati
panu (Zakuona kwa uthenga
wanga kwa inu). Ndithujye
Ngodziwa za akapolo Ake
(Zilakolako zawo) Ngowona
(zochita zawo).
97. Ndipo yemwe Mulungu
wamuongola, (Chifukwa cha
kukonzeka kwake kwa ubwino),
&*^j&&&$&
*&$&&*
<3^y t^ V^^^i&l^^
Surat 17. Al-Isra' Juzu 15
605
>o tjA-i
\ V frlj-yi dj>-
lyeyo ndi amene waongoka; ndipo
amene Wamulekerera kusokera,
(chifukwa cha kuipa Kwa
khalidwe lake), simungampezere
Athandizi kupatula lye (Mulungu).
Ndipo pa tsiku la chiweruzo
tidzawasonkhanitsa Uku
akukokedwa ndi nkhope zawo Ali
osapenya, osalankhula ndi osamva.
Malo awo okhala ndi ku
Jahannama. Nthawi iliyonse
(motowo) ukatotobwa,
Tidzauonjezera kwa iwo kuyaka
mwaukali.
98. (Chilango) chimenecho
ndiyo mphoto Yawo chifukwa cha
kusakhulupirira Kwawo zisonyezo
(zomwe tidaziimika Kwa iwo), ndi
kunena kwawo koti: M Kodi
tikadzakhala mafupa ndi Zidutswa
zonyenyekanyenyeka,
Tidzaukitsidwanso kukhala
zolengedwa Zatsopano?"
99. Kodi (onyalanyaza)
sadadziwebe kuti Mulungu Yemwe
adalenga thambo ndi Nthaka
Ngokhoza kulenga ena onga Iwo?
Ndipo wawaikira nthawi
(Yodziwika) yopanda chikaiko,
(Yowaukitsira ku imfa). Koma
achinyengo Akukana (zonsezi)
koma Kusakhulupirira basi.
100. Nena (kwa Amshirikina):
"Mukadakhala kuti Muli nazo
nkhokwe za chifundo cha Mbuye
ly&*&3$&®&
Surat 17. Al-Isra' Juzu 15
606
>o tji-i
> V ^y 3jj--
Wanga, mukadachita umbombo
(posagawira Ena) kuopa umphawi
chifukwa munthu Ali ndi khalidwe
loumira".
101. Ndipo ndithu, tidampatsa
Musa zizizwa zoonekera Zisanu
ndi zinayi (komabe
Osakhulupirira sadazikhulupirire).
Afunse ana a Isiraeli pamene
Adawadzera, Farawo adati kwa iye
(Musa): "Ndithu, ine ndikukuona
Iwe Musa kuti walodzedwa."
102. (Musa) adati: "Ndithu,
wadziwa Kuti palibe amene
watumiza (mitsutso) Iyi kupatula
Mbuye wathambo ndi Nthaka kuti
zikhale chiphanula maso. Koma
ine ndikukuona iwe Farawo Kuti
waonongeka."
103. Choncho (Farawo) adafuna
kuwatulutsa m'dziko La Iguputo
(Musa ndi ana a Isiraeli) Koma
tidammiza iye ndi onse omwe
adali nawo.
104. (Musa ndi anthu ake
tidawapulumutsa). Ndipo
tidati,kwa ana a Isiraeli, (Pambuyo
pommiza Farawo): "Khalani
M'dziko (loyera la shamu); "ndipo
Likazadza lonjezo lamoyo
winawo, Tidzakubweretsani
nonsenu (muli M'chipwirikiti.)
105. Ndipo chifukwa
chobweretsa choonadi Padziko
tygXL'A
&&±&m&j&
*} 9 S\'X< - 9 i*i ' **><SJ* 9 Vfc
^■A*S(j^J
%
mfoG$3y%®@p
Surat 17. AMsra' Juzu 15
607
>o *j*-i
) V ^j~-?1 5jj~-
tidaitumiza (Qur'an); Ndipo
mwachoonadi, Idavumbulutsidwa.
Ndipo sitidakutume (Ndichina)
koma kuti ukhale wouza
(Okhulupirira) nkhani zabwino,
ndi Wochenjeza (osakhulupirira).
106. Ndipo Qur'an iyi taigawa
(m'zigawo Zosiyanasiyana
poivumbulutsa Pang'onopang'ono)
kuti uwawerengere Anthu mwa
chifatse Ndipo taivumbulutsa
pang'onopang'ono (Muzaka 23).
107. Nena (kwa osakhulupirira
a m'Makka Mowachenjeza):
"Ikhulupirireni (Iyi Qur'an) kapena
musaikhulupirire, (Zonse zili
m'chifuniro chanu.) Ndithu, amene
adapatsidwa nzeru kale
(Yozindikira za m'mabuku a
Mulungu Qur'an isanadze)
ikamalakatulidwa kwa iwo
(Qur'aniyi) amagwa ndi zibwano
zawo Molambira.
108. Ndipo amanena: "Mbuye
wathu Ngoyera! Ndithu, lonjezo la
Mbuye wathu ndi
Lokwaniritsidwa! "
109. Ndipo amagwa ndi
zibwano zawo uku akulira, Ndipo
(Qur'an) imawaonjezera
Kudzichepetsa.
110. Nena (kwa Amshirikina):
"Mpempheni Mulungu, m'dzina la
Allah kapena Mpempheni m'dzina
*&j$m
^Wfl*W^?0j6
fc**3£j
9 9 9 f\
®S8g^&&#W3i$
Surat 17. Al-Isra' Juzu 15
608
>o ^\
> V t\jJ$\ ojj-*
la Rahman: Kapena dzina lililonse
limene Mungamtchulire
(zithandizabe); lye ali nawo maina
abwino. Ndipo Usawerenge
(Qur'an) paswala yako Ndi mawu
okweza, ndiponso Usatsitse mawu
kwambiri, koma Tsata njira
yolingana pakati Pazimenezo
(pokweza kwambiri kapena
Kutsitsazedi)."
111. Ndipo nena:
"Kutamandidwa Kwabwino nkwa
Mulungu, Yemwe saadadzipangire
Mwana, ndipo alibe m'phatikizi
Mu ufumu (Wake); ndipo alibe
Mthandizi (womthandiza)
Mkufooka; ndipo mkuzeni,
Kumkuza kwakukulu!"
Surat 18. AI-Kahf Juzu 15 I 609 I >° *& ^ A ca$&i «;>*
SURAT AL-KAHF XVIII . ^#^| j
Sura iyi idavumbulutsidwa ku Makka kupatula aya ya 38 ndi
ay a zomwe zayambira pa 83 mpaka kumalekezero kwake. Ndiye
kuti aya 29 zidavumbulutsidwa ku Madina. Surayi yayamba
ndikuyamika Mulungu wapamwambamwamba, chifukwa
chotumiza Qur'an yolemekezeka. Ndipo yafotokoza kuti Qur'an
udindo wake nkuchenjeza anthu oipa, ndikuuza anthu olungama
nkhani yabwino. Komanso ikuchenjeza anthu omwe akunamizira
Mulungu kuti adabala mwana.
Msurayi mwatchulidwa khama la Mtumiki (SAW)
mkufunitsitsa kwake kuti amene akuwaitanawo, akhulupirire
Mulungu. Ndipo mwatchulidwanso nkhani ya eni mphanga
amene adakagona mphangamo ndipo kenako nkuzutsidwamo
pambuyo pokhalamo ali chigonere kwa zaka zikwi zitatu (300)
ndi zaka zisanu ndi zinayi (9).
Kameneka kadali kagulu ka Akhirisitu komwe kadathawa
kwawo chifukwa chakupondereza kwa mfumu yawo ya
chiroma. Ndipo panthawi yonse yatchulidwayi kaguluko kadali
mtulo kuphanga. Kenako Mulungu adawaukitsa monga munthu
amaukira kutulo. Izi zidachitika kuti chikhale chisonyezo
chakuti Mulungu akhozadi kuukitsa anthu ku imfa.
Ndipo kenako Chauta walamula Mtumiki wake (SAW) kuti
aziiwerenga Qur'an ndikuchenjeza anthu oipa, ndikuuza anthu
zabwino za iyo (Qur'an). Ndipo wafotokozanso mwatsatanetsatane
momwe anthu akumunda wamtendere adzakhalira, ndi
momwenso anthu akumoto adzakhalire. Ndipo Mulungu
waponya fanizo la anthu awiri. M'modzi waiwo ngolemera;
amanyadira chuma chake ndi ana ake pomwe wachiwiriyo
amanyadira Mulungu. Ndipo Chauta wafotokoza kuti kudalirika
kwa Mulungu ndiko kuli koona, osati chuma ndi ana. Ndipo
walongosolanso kuti zonse za m'dziko nzakutha. Koma tsiku la
(chimaliziro) Kiyama ndimtendere waukulu ndiponso chilango
chopweteka.
Surat 18. Al-Kahf Juzu 15 I 610 I >° *>» ^ A u^» oj^*
Mulungu msurayi watchulanso nkhani ya Musa pamodzi ndi
munthu wabwino yemwe adapatsidwa nzeru zododometsa ndi
Mulungu. Ndipo m'nkhani imeneyi muli chithunzi chakuti
munthu angakhale ndi nzeru chotani, pali zinthu zambiri zomwe
zili kutali ndi nzeru zake ngakhale munthuyo atakhala mtumiki
wa Chauta. Koma pokhapokha Mulungu atamzindikiritsa za
zimenezo.
Kenako m'surayi mwatchulidwa nkhani ya Zul Qarnain
yemwe adafika kuvuma ndi kuzambwe ndikuti iye adamanga
chimpanda cholimba. Ndipo kenako yadza nkhani ya tsiku la
Kiyama ndi zochitikachitika zake za tsikulo.
Surayi yamaliza ndikufotokoza mphoto ya okhulupirira tsiku
la Kiyama (chimaliziro) ndi kuti nzeru za Mulungu ndi mawu
ake sizitha. Ndikufotokoza zanjira imene tingatsate pofuna
chiyanjo Chake.
Surat 18. Al-Kahf Juzu 15
611
>a tjA-t
> A ui^Jl Sj^-
Surat Al-Kahf XVIII
'."4a\W'i
M'dzina la Mulungu waChifundo
Chambiri, waChisonl
1. Kutamandidwa konse
kwabwino nkwa Mulungu, Yemwe
adatumizira kapolo Wake
(Mtumiki Muhammad{SWA}),
Buku (ili Lopatulika), ndipo
Sadalikhotetse (koma m'menemo
Muli zoona zokhazokha.)
2. (Walichita kukhala) loongoka
kuti Lichenjeze anthu zachilango
Chokhwima chochokera kwa lye
(Mulungu), Ndikuti liuze nkhani
yabwino amene Akhulupirira
omwe akuchita zabwino, Kuti
adzapeza malipiro abwino.
3. Adzakhalamo (mumtendere
wosathawo) Muyaya.
4. Ndikuti liwachenjeze amene
akunena (Kuti): "Mulungu
wadzipangira Mwana."
5. Iwo pabodza lawolo alibe
kuzindikira chinthu Chilichonse
chanzeru ngakhale makolo awo.
Lakula kwabasi liwu lomwe
likutuluka mkamwa Mwao. Sanena
china koma bodza basi.
6. Mwina udziwononga wekha
pakuwadandaulira Chikhalidwe
chawo kuti Sakhulupirira nkhani
5 .w*$&:
o&£\^\&\j
j&
'VV-*
<5WS3?«a3J*c^B
Surat 18. Al-Kahf Juzu 15
612
> o frji-i ) A J^3\ 3jj--
iyi. (Iyayi! Usakhale wodandaula
ndi zimenezo).
7. Ndithu, Ife tazichita zomwe
zili pamwamba Panthaka kukhala
zokometsera nthakayo, Ndikuti
(mwaizo) tiwayese mayeso kuti
(ndani) Mwaiwo ali wochita
zabwino kwambiri.
8. Ndipo ndithu, Ife ndi Amene
tidzazichita Zomwe zili pamenepo
kukhala monga Nthaka yoguga
(yopanda mmera).
9. Kodi ukuganiza kuti eni
phanga ndi Eni nkhani zomwe
zidalembedwa M'mabuku, adali
mwa zizindikiro Zathu
zododometsa kwambiri? (Iyayi,
zilipo zododometsa kwabasi
Kuposa zimenezo.)
10. Pamene anyamata
adathawira Kuphanga nati:
"Mbuye wathu! Tipatseni chifundo
chochokera kwa Inu, ndipo
tikonzereni chiongoko M'zochita
zathu". 1
© b^t^^^^U^^*^iSlS
W* W ij^j <W*> Ojoj ^V^l
1 Nkhani ya eni phanga monga momwe adaifotokozera omasulira Qur'an, idali
motere:-
Mfumu yomwe idapondereza anthu inkatchedwa Dikiyanusu idali mu M'zinda
wina kudziko la Roma umene unkatchedwa Tartusi, Mneneri Isa atapita kale.
Mfumuyi idali kuitana anthu kuti azipembedza mafano. Ndipo imapha aliyense
wokhulupirira mwa Mulungu amene sadali kuvomereza uthenga wake
wopotokawo kufikira chisokonezo ndi masautso zidawakulira anthu
okhulupirira Mulungu. Anyamata omwe adali okhulupirira Mulungu ataona
zimenezo, anadandaula kwambiri. Ndipo nkhani ya anyamata idamufika
mfumu wopondereza anthuyo ndipo adatumiza mithenga kuti akawatenge
anyamatawo. Anyamatawo pamene adaimirira pamaso pa mfumu, iyo
idawaopseza kuti iwapha ngati akana kupembedza mafano ndi kukana
Surat 18. Al-Kahf Juzu 15 I 613 I >° *>» >A J^\ oj^
kupereka nsembe. Koma iwo adatsutsana nayo naonetsera poyera
chikhulupiriro chawo mwa Mulungu. Adati: "Mbuye wathu ndi Mbuye
wathambo ndi nthaka. Sitingapembedze mulungu wina kusiya lye".
Mfumu idati kwa iwo: " Inu ndinu anyamata amisinkhu yochepa, choncho
ndikukupatsani mwayi mpaka mawa kuti mukaganize bwino." Tero iwo
adathawa usiku namdutsa m'busa yemwe adali ndi galu. M'busayo pamodzi
ndi galu wake adawatsatira, ndipo pamene kudacha adabisala m'phanga
lalikulu lam'phiri. Mfumu pamodzi ndi ankhondo ake, adawatsatira mpaka
kukafika kuphangalo. Koma anthu ake adaopa kulowa m'phangamo ndipo
mfumu idati: "Atsekereni khomo laphangali kuti afere komweko ndi njala ndi
ludzu. Ndipo Mulungu adawagoneka tulo anyamata a kuphanga aja; adakhala
ali mtulo chigonere osadziwa kanthu mpaka padapita zaka zikwi zitatu (300)
ndi zaka zisanu ndi zinayi (9). Kenako Mulungu adawaukitsa. Ndipo iwo
amaganiza kuti akhala kuphangako tsiku limodzi, kapena theka la tsiku. Ndipo
adayamba kumva njala namtuma m'modzi wawo kuti akawagulire chakudya.
Koma adamulangiza akadzibise ndiponso akachenjere kuti anthu asamuzindikire.
Choncho iye adapita mpaka kukafika m'mudzimo. Kuja anapeza zizindikiro za
mudziwo zasintha.
Palibe aliyense mwanzika zam'mudzimo amene adamdziwa. Yekha
adadzinong'oneza "Mwinatu ine ndasokera njira yakumudzi kwathu kuja".
Komabe adagula chakudya. Ndipo pamene adapereka ndalama kwa
wogulitsa adayamba kuitembenuzatembenuza ndalama ija m'manja mwake.
Adati: "Mwaipeza kuti ndalama iyi?" Choncho anthu adasonkhana
nayang'ana ndalama ija modabwa nati: "Kodi mnyamata iwe ndiwe yani,
kapenatu mwatulukira chuma chomwe chidabisidwa m'nthaka ndi anthu
akale?" lye adati kwa iwo "lyayi. Ndikulumbira Mulungu, sindidapeze chuma
chokwiriridwa m'nthaka. Iyi ndi ndalama yomwe mtundu wanga umagwiritsa
ntchito". Iwo adati kwa iye: "Ndalamayi njakale kwambiri, m'nyengo ya mfumu
Dikiyanusu". lye adati modabwa: "Adatani Dikiyanusiyo?" Iwo adati, "Adafa
kalekale!" lye adati:" Ndikulumbira Mulungu, sangandikhulupirire aliyense
zimene nditi ndikuuzeni. Ife tidali anyamata. Ndipo Mfumuyo idatikakamiza
kupembedza mafano. Choncho tidaithawa usiku wadzulo nkupita kukabisala
kuphanga. Tere lero anzanga andituma kuti ndikagule chakudya. Choncho
tiyeni pamodzi kuphangalo kuti nkakuonetseni anzangawo. Iwo adadodoma
ndi zonena zakezo nadziwitsa mfumu ya nthawi imeneyo nkhani za
munthuyu. Mfumuyo idali yokhulupirira Mulungu. Ndipo iyo itamva nkhaniyi,
idapita pamodzi ndi ankhondo ake ndi nzika za m'mudziwo. Atafika kuja
pafupi ndi phangalo, anthu akuphangalo adamva phokoso ndi migugu
yamahatchi ndipo adaganiza kuti adali ankhondo a Dikiyanusu. Choncho onse
adaimirira kupemphera. Ndipo mfumu idalowa nkuwapeza akupemphera.
Pamene adamaliza kupemphera mfumu idagwirana nawo chanza niiwauza
kuti iyo imakhulupirira Mulungu, ndikuti Dikiyanusu adamwalira kalekale.
Kenako mfumuyo idamvera nkhani yawo niidziwa kuti, Mulungu wawaukitsa
kuti chikhale chisonyezo kwa anthu kuti Mulungu adzawaukitsa anthu akufa.
Kenako Mulungu adawagonekanso natenga mizimu yawo iwo ali mtulo
chomwecho. Ndipo anthu adayamba kunena: "Timange Msikiti pomwe pali
iwowapa wopembedzamo Mulungu".
Surat 18. Al-Kahf Juzu 15
614
\ o tji-i \ A Jl^\ ojj~>
11. Tidagonthetsa makutu awo,
(ndikugona Kosamva nako kanthu)
kwa zaka Zambirimbiri m'phanga
12. Kenako tidawautsa, kuti
tiwayese (Kuti) ndani mwa magulu
awiriwa Amadziwa kuwerengera
nthawi imene (Anyamatawa)
adakhala (m'phangamo).
13. Ife tikusimbira (iwe
mtumiki{SAW}) Nkhani zawo
mwachoonadi; ndithu, Iwo adali
anyamata amene Adakhulupirira
Mbuye wawo, ndipo
Tidawaonjezera chiongoko.
14. Ndipo tidalimbikitsa mitima
yawo pa Chikhulupiriro pamene
Adaimirira (pamaso pa mfumu
yawo Yosakhulupirira) ndikunena:
"Mbuye wathu ndi Mbuye wa
thambo Ndi nthaka. Ndipo
sitipembedza Mulungu wina
m'malo mwa lye. Ngati titatero
ndiye kuti tanena Zoipa zopyola
muyeso.
15. Awa anthu athu adzipangira
Milungu ina kusiya Mulungu,
nanga Bwanji sakubweretsa pa
zaiyo ( milunguyo) Umboni
woonekera (wosonyeza kuti Iyo
ndi milungudi)? Kodi ndani
Wachinyengo wamkulu woposa
yemwe Akupekera bodza Mulungu?
16. (Adauzana pakati pawo)
"Ndipo ngati Muwapatuka
©bo*' ti&2
^S^ss^j^^^
Siirat 18. AI-Kahf Juzu 15
615
>o *j*-i
y A J14&1 5jj--
ndizimene akuzipembedza Kusiya
Mulungu, thawirani kuphanga;
Mbuye wanu akutambasulirani
chifundo Chake
ndikukufewetserani zinthu Zanu
zonse".
17. (Zidali tere) ukadakhala
ukuliona Dzuwa pamene
linkatuluka (ndikuyamba
Kukwera), ukadaliona
likulambalala Kumbali kwa
phanga lawo, mbali
Yakudzanjadzanja, ndipo pamene
linkalowa Limawadutsa mbali
yakumanzere (Popanda
kuwalunjika) pomwe iwo adali
Pamtetete mmenemo. Zimenezo
ndi Zina mwa zisonyezo za
Mulungu (Zosonyeza kukhoza
Kwake). Ndipo Amene Mulungu
wamuongola iyeyo ndiye
Woongoka; ndipo amene
wamulekerera Kuti asokere,
simungampezere Mtetezi kapena
muongoli.
18. Ndipo ungawaganizire kuti
ali maso Pomwe iwo ali mtulo,
uku Tikuwatembenuzira mbali
yakumanja ndi Yakumanzere (kuti
nthaka isadye matupi awo) Ukunso
galu wawo atatambasula miyendo
yake (Yakutsogolo) pakhomo ngati
Ukadawaona ukadatembenuka
Kuwathawa; ndithu,
ukadadzadzidwa Mantha ndi iwo.
Surat 18. Al-Kahf Juzu 15
616
\ o *j£-i ) A ol^\ 5jj--
19. Ndipo momwemonso
tidawaukitsa kuti afunsane Pakati
pawo (zanthawi imene akhala ali
Chigonere). Adanena wonena mwa
iwo: "Kodi mwakhala nthawi
yotani muli Mtulo?" Adati,
"Takhala tsiku limodzi Kapena
gawo la tsiku." (Ena) adati:
"Mbuye wanu akudziwa kwambiri
za Nyengo imene mwakhala.
Choncho mtumeni Mmodzi wa inu
ndindalama zanuzi za Siliva
kumudzi ndipo akayang'ane
chakudya Chake nchotani chomwe
chili choyera bwino, Ndikubwerera
nacho chakudyacho; koma izi
Akachite mochenjera ndipo
asamzindikiritse Aliyense za inu. ]
20. "Ndithu iwo akakudziwani
(pamene Mulipa), akugendani ndi
miyala; Apo ai akubwezerani
kuchipembedzo Chawo
(chopotoka), zikatero ndiye Kuti
simdzapambananso mpaka
kalekale.
21. (Koma anthu anazindikira
pamene Adaona ndalama yakale),
momwemonso Tidawazindikiritsa
(kwa anthu) kuti Adziwe kuti
99 '9 * 9 9' * ' ' 9?'.\ '£' ' ftf *.
1 Omasulira Qur'an adati:-
Adalowa kuphangako nthawi yam'bandakucha, ndipo Mulungu adawaukitsa
madzulo. Ichi nchifukwa chake ena ankati akhala theka la tsiku poganizira kuti
adakhalamo usana umodzi.pomwe ena amati adakhala tsiku lathunthu.Kenako
nati Mulungu ndi amene akudziwa nyengo imene takhalamo. Ndime iyi
ndiumboni waukulu wotsimikiza kuti mizimu ya anthu abwino sidzaona
kutalika nyengo vokhalira m'manda.
Surat 18. Al-Kahf Juzu 15
617
)o *>»
\ A uA^Jl 3j^»
lonjezo la Mulungu (Loukitsa ku
imfa zolengedwa) nloona, Ndikuti
nthawi yachimaliziro njosa-
Kaikitsa (ndipo kumbukani)
pamene Adakangana pakati pawo
pachinthu Chaochi, ena adati:
"Mangani Chomanga pa iwo (kuti
anthu Asamadze
kudzawasuzumira) Mbuye Wawo
za iwo Akudziwa bwino Koma
amene adapambana paganizo
Lawolo adanena: "Ndithu, ife
timanga Msikiti wa iwowa
(paphanga lawoli)."
22. (Ena) akhala akunena (kuti)
adali anthu Atatu, wachinayi ndi
galu wawo; Ndipo (ena) akuti adali
asanu, wachisanu Ndichimodzi
ndigalu wawo. (Akunena)
mwakungoganizira chabe Zomwe
sakuzidziwa; ndipo (ena) akuti
Adali asanu ndi awiri, ndipo
Wachisanu ndi chitatu ndi galu
Wawo. Nena: "Mbuye wanga
ndiye Akudziwa bwinobwino
zachiwerengero chawo Palibe
amene akudziwa (zaiwo) koma ndi
Ochepa chabe " Choncho
usatsutsane Nawo za iwo, kupatula
kutsutsana kwa Pazinthu
zodziwika, ndipo usamfunse
Aliyense mwa iwo za iwo.
23. Ndipo usanene ngakhale
Pang'ono zachilichonse Kuti,
"Ndichitamawa."
4jU*Ml
&>b&§m,$'M%
Surat 18. Al-Kahf Juzu 15 I 618 I ^° *>' Uti^li 5j>-
24. Koma (utsogoze liwu ^\i)&5$Z&&\ %$$$[
lakuti); Insha'llah, (Mulungu ^%< x ^^ ' ,+ >< ^ *t '
akafuna!)" Ndipo mukumbuke St^Qj <^dcP-*U^
Mbuye wako ukaiwala ponena ®!6i*jiui<^
kuti: "Mwina Mbuye wanga
anditsogolera Panjira yapafupi
pachiongoko kuposa iyi." 1
25. Ndipo adakhala m'phanga
lawolo (ali mtulo) Zaka zikwi
zitatu (300) ndikuonjezera Zisanu
ndi zinayi (9) .
26. Nena: "Mulungu akudziwa
bwinobwino Nyengo imene (iwo)
adakhala; zobisika Zakumwamba
ndi za pansi nza lye (Mulungu
basi); taona Mulungu kuonetsetsa!
Taona Mulungu kumvetsetsa!
(Mulungu Ngoona chilichonse.
Ndipo Ngwakumva chilichonse).
Ndipo iwo alibe mtetezi Popanda
lye (Mulungu); ndipo lye sagawira
aliyense Udindo Wake wakulamula.
27. Ndipo werenga zomwe
Zavumbulutsidwa Kwa iwe za
m'Buku la Mbuye wako, palibe
Amene angathe kusintha mau
Ake, Ndipo nawe sungapeze
potsamira ndi Pothawira (kuti
Mulungu asakupeze.)
1 Ayuda adamufunsa Mneneri (madalitso ndi mtendere wa Mulungu zikhale pa
iye) zankhani ya anyamata a kuphangawo. lye adayankha kuti: "Ndikuuzani
mawa", sadanene kuti Mulungu akafuna ndikuuzani mawa."
Choncho chivumbulutso sichidadze kwa iye ndipo anavutika kwambiri kusowa
chowauza anthu aja. Kenako Mulungu adamuuza zoti ngati unena pa chinthu
kuti chimenechi ndichichita mawa, nenanso mawu oti ngati Mulungu afuna.
*riv
Surat 18. Al-Kahf Juzu 15
619
\ o tjA-i \ A J^\ Sj^-
28. Ndipo dzikakamize kukhala
pamodzi ndi amene Akupempha
Mbuye wawo m'mawa ndi
madzulo uku Akufunafuna nkhope
Yake; (chiyanjo Chake) Ndipo
maso ako asachoke pa iwo ndi
(Kuyang'ana ena) ncholinga
chofuna zokongoletsa Za moyo
wadziko lapansi; ndipo
usamumvere Amene mtima wake
tauiwalitsa kutikumbukira
Ndikumangotsatira zilakolako
zake, Ndipo zinthu zake nkukhala
zotaika (Zosalongosoka). 1
29. Ndipo nena (kwa
osakhulupirirawo, kuti) "Ichi ndi
choonadi chimene chachokera
Kwa Mbuye wanu": Choncho
amene afuna, Akhulupirire; ndipo
amene afuna, (Kusachikhulupirira)
asakhulupirire Ndithu, achinyengo
tawakonzera moto, Womwe
mipanda yake ikawazinga. Ndipo
Akapempha chithandizo (chifukwa
cha ludzu Loopsya lomwe
likawapeza), akathandizidwa
Popatsidwa madzi (otentha
kwambiri) Monga madzi a chitsulo
9 9 te*9\" '\\9' ?><&' {,'*"
\iZ£$*>*-* 'V*<."i
Ndime iyi idavumbulutsidwa pamene Uyaina Bun Huswaini ndi mnzake
adadza kwa Mtumiki ndi kumpeza atakhala pamodzi ndi omtsatira
(Maswahaba) osauka monga: Ammaru, Suhaibu ndi Bilali ndi ena onga iwo.
Iwo adati kwa Mtumiki "Ukadawapirikitsa anthu wambawa, ndiye kuti
tikadakhala nawe nkumamvera zimene ukulalikira.
Koma ife tikunyansidwa ndi ulaliki wako poona kuti nthawi zonse ukukhala ndi
anthu onyozeka amene simabwana". Choncho Qur'an idatsika kumuuza
mtumiki kuti "Usawathamangitse anthu omwe akupempha Mulungu m'mawa
ndi madzulo ngakhale ndi onyozeka".
Surat 18. Al-Kahf Juzu 15
620
> o frjA-t \ A oi$&i ojj~-
chosungunuka, Omwe adzasupula
nkhope zawo. Taona Kuipa
chakumwa! ndi kuipa malo
wotsamira!
30. Ndithu, amene akhulupirira
ndi kumachita Ntchito zabwino,
(tidzawalipira Paubwino
wawowo), ndithu, Ife Sitisokoneza
malipiro a amene wagwira Ntchito
yabwino.
31. 1 wo adzapeza minda
yamuyaya; yomwe Pansi ndi
patsogolo pake Pakuyenda
mitsinje; m'menemo
Adzawakongoletsa powaveka
zibangiri Zagolide, ndipo adzavala
nsalu Zobiriwira; zasilika
wopyapyala Ndi silika wokhuthala
uku atatsamira Makhushoni
mmenemo. Taonani Kukhala
bwino malipiro! Ndi pamalo
Potsamira pokongola (popeza
mpumulo Wabwino)!
32. Ndipo aponyere fanizo la
anthu awiri Mmodzi wa iwo
tidampangira minda Iwiri ya
mphesa ndi Kuizunguliza ndi
mitengo Yakanjedza; ndipo pakati
Pa iyo tidaikapo mbewu (zina).
33. Minda yonse iwiriyi
idapatsa Zipatso zake ndipo
siidapungule Chilichonse mzipatso
zake. Ndipo Pakati pake
tidapititsapo mitsinje.
Surat 18. AI-Kahf Juzu 15
621
> o *j£-t \ A J^\ 5j>-
34. Ndipo iye adali ndi chuma
(china) Nati kwa mnzakeyo
mokambirana Naye: "Ine ndili ndi
chuma Chambiri kuposa iwe,
(ndilinso) ndi Mphamvu zambiri
chifukwa cha Onditsatira (omwe
ndili nawo)."
35. Ndipo adalowa m'munda
mwake uku Akudzichitira yekha
zoipa. Adati: "Sindiganiza
ngakhale mpang'ono Pomwe kuti
(munda) uwu udzaonongeka;"
36. "Ndiponso sindiganiza kuti
Kiyama (chimaliziro)
Idzachitikadi. Ngati (itapezekadi
Kiyamayo), ine nkubwezedwa kwa
Mbuye wanga, ndithu, ndikapeza
malo Abwino wobwererako
kuposa awa. (Monga momwe
ndapezera mwayi kuno, Ukonso
ndikapeza, ngati Kiyamayo
Ilikodi)."
37. M'nzake adanena kwa iye
mokambirana naye "Kodi
ukumukana Yemwe adakulenga
ndi Dongo, kenako ndi dontho
lamadzi Aumuna ndiponso
adakupanga Kukhala munthu
wolingana?
38. Koma ine ndikukhulupirira
kuti Iye ndi Mulungu basi, Iyeyo
ndiye Mbuye Wanga, ndipo
sindiphatikiza aliyense Ndi Mbuye
wanga.
d&$&j®;&'&M
Surat 18. Al-Kahf Juzu 15
622 1 * *>'
^ A ui$&! 5j^»
39. Ndipo pamene umalowa
m'munda wako Ukadanena kuti izi
ndi zimene wandifunira Mulungu,
mphamvu sizikadapezeka Koma
kupyolera mwa Mulungu
(Zikadakhala zabwino kwa iwe).
Ngati ukundiona ine ndili ndi
chuma Chochepa ndi ana ochepa
kuposa iwe (Koma sindisiya
kutamanda Mulungu).
40. Mwina Mbuye wanga
angandipatse Zabwino kuposa
munda wakowo Ndi kuutumizira
mliri wachiphaliwali Kuchokera
kumwamba, Ndipo ndikusanduka
Nthaka yoterera (yoguga).
41. Kapena madzi ake
nkumangophwa Kotero kuti
sungathe Kuwapeza".
42. Tsono mliri unagwa pa
Zipatso zakezo (ndikuziononga
Motheratu), ndipo adayamba
kutembenuza Manja modandaulira
Zomwe adaonongera m'menemo;
(mindayo) Mitengo yake itagwera
pansi. Ndipo adati: "Kalanga Ine!
Ndikadapanda kumphatikiza
Mbuye wanga ndi aliyense
(Zoterezi sizikadachitika.")
43. Ndipo sadakhale ndi anthu
omthangata Pamene Mulungu
adamtaya, ngakhale iye Mwini
sadadzithandize.
Surat 18. Al-Kahf Juzu 15 I 623 I ^ ° tjk-\ \ A Ji^\ 5jj~-
44. Pamalo potere chitetezo
chimakhala Cha Mulungu yekha
woona, (Yemwe Ngwamuyaya.)
lye Ngolipira bwino, Ndiponso
Wabwino (pakudza) ndi
Malekezero abwino.
45. Ndipo aponyere fanizo la
moyo wadziko lapansi, Uli ngati
madzi Amene tikutsitsa kuchokera
kumitambo Kenako (madziwo)
amasakanikirana ndi Mmera
wam'nthaka (ndikuyamba kumera
Mokongola), kenako (mmerawo)
nkukhala Masamba ouma
odukaduka omwe mphepo
Ikuwaulutsa uku ndi uku. Ndipo
Mulungu Ali ndi mphamvu
pachilichonse.
46. Chuma ndi ana
ndizokometsera za moyo Wa dziko
lapansi, koma ntchito Zabwino
zopitirira ndizo zabwino Kwa
Mbuye wako, monga mphoto Ndi
chiyembekezo chabwino.
47. Ndipo (akumbutse) tsiku
lomwe Tidzayendetsa mapiri
(pouluka ngati Ubweya mu
mlengalenga), ndipo Udzaiona
nthaka ili tetetee, (Itatambasuka
yosakhwinyata Ndi mapiri kapena
zitunda), ndipo
Tidzawasonkhanitsa (tsiku
limenelo) Ndipo sitidzasiya
aliyense mwa iwo (Oyamba ndi
omaliza).
> 999 \'Ml< * 9 ^9t"£iC\'
Surat 18. Al-Kahf Juzu 15
624
^ © tji-l ^ A lA^3i 5j^*
48. Ndipo adzabwera nawo kwa
Mbuye wako Atandanda m'mizere
(ndikuuzidwa), "Ndithu,
mwatidzera monga tidakulengerani
Pachiyambi (opanda nsapato,
amaliseche Ndiponso opanda
chilichonse chuma ndi Ana).
Koma mumaganiza kuti
sitikuikirani Lonjezo (ili louka ku
imfa ndi kuweruzidwa)."
49. Ndipo kaundula adzaikidwa
(pamaso pawo) Ndipo udzaona
oipa ali oopa chifukwa Cha zomwe
zili m'menemo (mu kaundula),
Ndipo adzanena: "Kalanga ife
taonongeka! Ngotani kaundula
uyu! sasiya chaching'ono Ngakhale
chachikulu, koma zonse kuzilemba
ndipo Adzapedza zonse zimene
adazichita Zitalembedwa
m'menemo. Ndipo Mbuye wako
Sapondereza aliyense
(pomusenzetsa zomwe sizake,
Kapena kumchitira zomwe
sizikumuyenera).
50. Ndipo (kumbuka) pamene
tidawauza Angelo: "Mchitireni
sijida Adam (muweramireni
Momulemekeza)." Onse adachitadi
Sijida kupatula Iblis. lye adali
Mmodzi wa ziwanda, ndipo
adatuluka M'chilamulo cha Mbuye
wake. Kodi lye ndi mbumba yake
mukuwalola Kukhala abwenzi
(anu) kusiya Ine, Pomwe iwo ndi
Surat 18. Al-Kahf Juzu 15
625
>0 «j*-l
^ a c^4^i' ojj--
adani anu? Taonani kuipa kusintha
kwa anthu oipa!
51. Sindidawachite (iwo)
kukhala mboni Nkulenga kwa
thambo ndi nthaka, Ngakhale
kuwalenga kwawo ndipo
Sindidawalole osokeretsa Kukhala
athandizi (Anga).
52. Ndipo (kumbukani) tsiku
lomwe (Mulungu) Adzanena:"
Aitaneni aja Omwe
munkandiphatikiza nawo omwe
Munkati (ndi milungu inzanga)"
Choncho, adzaiitana koma
siidzawayankha; Ndipo tidzaika
chionongeko pakati pawo (Ndipo
sadzakumananso).
53. Ndipo woipa adzauona
moto (panthawi Imeneyo)
ndikutsimikiza kuti iwo alowa
M'menemo. Ndipo moto wo
Sadzapeza pouzembera.
54. Ndipo ndithu,
tawafotokozera anthu
Mwatsatanetsatane m'Qur'aniyi
fanizo La mtundu uliwonse; koma
munthu Wapambana chinthu
chilichonse pamakani.
55. Ndipo palibe chimene
chaletsa anthu Kukhulupirira
pamene chiongoko choonadi
Chawadzera ndikupempha
chikhululuko Kwa Mbuye wawo,
koma akuyembekezera Kuti
Surat 18. Al-Kahf Juzu 15
626
>s *>H
\ A ci$&1 Ojj-»
chiwadzere chikhalidwe cha anthu
Oyamba, kapena chiwadzere
Chilango masomphenya.
56. Ndiponso sitituma atumiki
(ndi cholinga choti Adzetse
chilango), koma kuti akhale Onena
nkhani zabwino ndi ochenjeza.
Ndipo amene sadakhulupirire,
akuchitira Makani chabodza kuti
kupyolera M'chabodzacho kuti
achotse choonadi, ndipo Ay a
Zanga ndi zomwe achenjezedwa
nazo, Akuzichitira chibwana!
57. Kodi ndani woipitsitsa
kwabasi Woposa yemwe
akukumbutsidwa ndi aya Za
Mbuye wake, koma iye
nkuzinyoza, Ndipo nkuiwala
(zoipa) zimene manja Ake
adatsogoza?Ndithu Ife taika
M'mitima mwawo zitsekerero kuti
asazizindikire. Ndiponso
M'makutu mwawo mwalemedwa
ndi ugonthi. Ndipo ukawaitanira
kuchiongoko (choonadi), Salola
kuongoka ngakhale pang'ono.
58. Ndipo Mbuye wako
Ngokhululuka kwambiri Mwini
chifundo. Ndipo akadawathira
Dzanja pa zoipa zomwe akhala
akuchita, Ndiye kuti ndithu,
akadawapatsa chilango
Mwachangu; koma iwo ali nalo
lonjezo Ndipo sadzapeza
pothawira paliponse Ndikulipewa.
®^S
'*-'-.Ql
Surat 18. AI-Kahf Juzu 15 | 627 \>° *> j * * Jl^S\ 5jj~>
59. Ndipo imeneyo ndi midzi
tidawaononga (okhalamo) Pamene
adadzichitira zoipa okha; ndipo
Tidawaikira lonjezo lanthawi
yoikidwa La kuonongeka kwawo.
60. Ndipo (kumbukani) pamene
Musa adanena Kwa Mnyamata
wake (Yushau Nuni), "Ndipitiriza
kuyenda kufikira ndikafike
Pamajiga panyanja ziwiri, kapena
ndizingoyenda Zaka ndi zaka
(kufikira nditakumana Naye amene
ndikumfunayo)."
61. Choncho pamene adafika
pamajiga (Pa nyanja ziwirizo)
adaiwala Nsomba yawo yomwe
idatenga Njira yake kunka
m'nyanja ngati una (Musa
Adaiwala kumfunsa mnyamata
wake Za nsombayo; naye
mnyamata Adaiwala
kumfotokozera Musa zomwe
Zidachitika ndi nsombayo).
62. Pamene adapita patsogolo,
adauza Mnyamata wake, (kuti):
"Tipatseni Chakudya chathu
chamasana; ndithu Paulendo
wathuwu takumana ndi zotopetsa."
63. (Mnyamata) adati: "Kodi
mwaona Pamene tidapumula paja,
pathanthwe Ndipomwe ndidaiwala
(kuti ndikuuzeni) Za nsombayo
ndipo palibe Wandiiwalitsa koma
Satana basi, kuti Ndisaikumbukire.
3RSX2S®iJQ&®ii&
<"'$&'-" ™
Surat 18. Al-Kahf Juzu 15
628
> o tjJUi y A Jl£3\ ojj^
Iyo idatenga njira Yake kunka
m'nyanja, mododometsa."
64. (Musa) adati : M Pamenepo
ndi pomwe Timafuna." Choncho
adabwerera M'mbuyo potsatira
njira yawo (Yomweyo).
65. Ndipo adampeza kapolo
yemwe ndi m'modzi Wa akapolo
athu amene tidampatsa Chifundo
chochokera kwa Ife, (yemwenso)
Tidamphunzitsa maphunziro
ambiri Kuchokera kwa Ife.
66. Musa adati kwa iye: "Kodi
Ndingakutsate kuti undiphunzitse
Chiongoko chomwe
waphunzitsidwa? "
67. Adati: "Ndithu, iwe siutha
kupirira Nane! (Uwona zomwe
sungathe kupirira Nazo). M
68. "Kodi ungapirire bwanji
ndi zinthu Zomwe sukuzidziwa
chinsinsi chake?"
69. (Musa) adati: "Ngati
Mulungu afuna, Undipeza ndili
wopirira; ndipo Sindinyoza lamulo
lake"
70. Adati: "Ngati unditsata
usandifunse Za chilichonse
(chimene uchione) kufikira Ine
nditakuuza."
71. Choncho onse awiri
adanyamuka mpaka Adakakwera
m'chombo; ndipo adachiboola
\4? \4f< 9 9)94"rs 9
Surat 18. Al-Kahf Juzu 16
629 ^ 1 *>■»
S A Jl^3\ 6jj~>
(Chombocho). (Musa) adati: "Kodi
Wachiboola kuti uwamize ali
m'menemo? Ndithu, wachita
chinthu chachikulu Choipa." 1
72. Adati: "Kodi sindidanene
kuti iwe Sutha kupirira nane?"
73. (Musa) adati:
"Usandidzudzule Chifukwa
chakuiwala kwanga, ndipo
Usandipatse zovuta kwambiri
Pakhumbo langali (lofuna
kukutsata)".
74. Ndipo adanyamuka; mpaka
pomwe adakumana Ndi
m'nyamata wochepa, ndipo
(M'neneri Khidhir) adamupha.
Musa adati: u Ha! Waphamunthu
wopanda cholakwa, Pomwe sadaphe
munthu mnzake? Ndithu, Wachita
chinthu choipitsitsa kwabasi".
75. Adati: "Kodi sindidakuuze
(kuti) Ndithu, iwe sutha kupirira
nane?"
76. (Musa) adati: "Ngati
ndikufunsanso Chilichonse
pambuyo pa ichi, Usandilole
kutsagana nawe. Ndiye Kuti
wakwaniritsa dandaulo lako pa ine".
rifi&3$i0$$d&
@\j&>(jf
1 Tanthauzo lake nkuti pamene onse awiri adanyamuka adali kuyenda
m'mphepete mwanyanja kufikira chombo chidawadutsa. Eni chombowo
adamdziwa Khidhiru nawakweza onse awiri popanda malipiro. Atakwera
m'chombomo Khidhiru adatenga nkhwangwa ndi kuzula thabwa limodzi la
m'chombomo pomwe chombocho chidali pakatikati panyanja.
Musa ataona anati: "Bwanji ukuboola chombo pomwe anthuwa atinyamula
mwaulere?" Ndipo adatenga kasanza nkuika pomwe panachotsedwa thabwapo.
Surat 18. Al-Kahf Juzu 16
630
n *>»
^ a Jl£s\ 5jj--
77. Choncho adamuka; kufikira
pamene Adawapeza eni mudzi
ndipo adawapempha Eni mudziwo
chakudya, koma adakana
Kuwalandira monga alendo. Ndipo
adapezamo khoma lili pafupi
kugwa, (Ndipo Mneneriyo)
adaliimika. (Musa) Adati: "Ngati
ukadafuna , ukadalandira Malipiro
(pantchitoyi kuti tigulire Chakudya)".
78. (Khidhiri) adati: "Awa
ndiwo malekano Pakati pa ine ndi
iwe. Tsopano ndikuuza tanthauzo
la zomwe Sudathe kupirira nazo. 1
79. "Tsopano chombo chija,
chidali cha Masikini ochita ntchito
panyanja, ndipo Ndidafuna
kuchiononga (mwadala) chifukwa
Patsogolo pawo padali mfumu
yomwe Imatenga chombo
chilichonse (chabwino) Molanda."
80. "Ndipo mnyamata uja,
makolo ake adali Okhulupirira,
ndipo tidaopera Kuti
angawachititse zoipa (makolo
akewo) Ndi za kusakhulupirira
(Mwa Mulungu).
81. Choncho tidafuna kuti
Mbuye wawo Awasinthire ndi
wabwino kuposa iye Pakuyera, ndi
wachifundo chapafupi (Kwa
makolo ake.)"
1 Mtumiki Muhammad (SAW) adati pankhani iyi ya Musa ndi Khidhiri, Mulungu
amchitire chifundo Musa. Ndikulakalaka kuti iye akadapirira kukhala limodzi
ndi mnzakeyo, akadaona zodabwitsa, ndipo Mulungu akadatisimbira zambiri za iwo.
Sural 18. Al-Kahf Juzu 16
631
> "\ *jJ-i \ A ci^Jl «j_j--
82. "Tsopano chipupa chija,
chidali cha ana awiri amasiye
mumzindamo; Ndipo pansi pake
padali chuma chawo (Chimene
adawasiira bambo wawo) ndipo
Tate wawo adali munthu wabwino
Choncho Mbuye wako adafuna
kuti akule misinkhu yawo ndipo
adzadzitulutsire chuma chawocho;
Ichi ndi chifundo chochokera kwa
Mbuye wako. Ndipo ine
sindidachite zinthu Zimenezi
mwandekha. Limenelo ndilo
tanthauzo la zomwe sudathe
kupirira nazo".
1 Nkhani ya Musa ndi Al-Khidhiri yomwe ikupezeka mu Sahihi Bukhari ndi
Muslim, Ubayu bun Kaabi adailandira kuchokera kwa Mtumiki wa Mulungu
(SAW) kuti iye adati: Ndithudi, Musa adaimirira kulalikira kwa ana a Isiraeli,
ndipo adamufunsa kuti: "Ndani mwa anthu yemwe ngodziwa kwambiri?" lye
adati: "Ndine." Ndipo Mulungu adamudzudzula payankho lake lotere.
Choncho Mulungu adamuzindikiritsa iye nati: "Ndithu, ine ndilinaye kapolo
pamajiga panyanja ziwiri yemwe ngodziwa kwambiri kuposa iwe".
Musa adati: "E, Mbuye wanga! Ndingampeze bwanji iyeyo"? Mulungu adati:
"Tenga nsomba, uiike muswanda (Basikete). Pamene nsombayo ikakusowe,
ndiye kuti iye ali pamenepo." Tero Musa pamodzi ndi mnyamata wake (Yusha
Bun Nun) adaubutsa ulendo mpaka kukafika pathanthwe. Adasamiritsa mitu
yawo pamenepo mpaka kugona tulo. Ndipo nsomba idapiripita m'swanda
muja, nkutuluka kukagwera mnyanja. Koma Mulungu adamanga kuyenda kwa
madzi pamene nsombayo idagwera adangounjikana chimulu pompo.
Pamene adauka, mnyamata uja adaiwala kumuuza zansombayo, naayenda
usana ndi usiku kufikira mmawa mwake mwa tsiku limenelo. Musa adati kwa
mnyamata wake, "Tipatseni chakudya chathu cham'mawa; ndithu tapeza
zotopetsa paulendo wathupa".Adati Musa sadamve kutopa kufikira pamene
adadutsa pamalo pomwe Mulungu adamulamulapo -. Mnyamata wake adati:
"Kodi mwaona? Titafika pathanthwe ine ndidaiwala nkhani yansomba ija.
Komatu palibe amene wandiiwalitsa kuikumbukira, koma Satana basi.
Idatenga njira yake kunka m'nyanja mododometsa". Musa adati: "Pamenepo
mpomwe timafuna". Choncho adabwerera kulondola mapazi awo mpaka
kukafika pathanthwe lija. Apo adaona munthu atadzifundika nsalu. Musa
adampatsa salaamu, ndipo Al-Khidhiri adati: "Yachokera kuti salaamu yotere
m'dziko lako! Kodi ndiwe yani? Adati "Ine ndine Musa". lye adati Musa wa ana
a Isiraeli?" Musa adavomera kuti Inde, ndadza kuti mundiphunzitse zomwe
Siirat 18. Al-Kahf Juzu 16 I 632 I ^ *j*-» ^ A J4&1 «jj~-
83. Ndipo akukufunsa nkhani za
Zul-Qarnain. Auze:
"Ndikulakatulirani zina Mwa
nkhani zake".
84. Ndithu, tidampatsa
mphamvu Zokhalira padziko
ndikumpatsa Njira yopezera
chilichonse
85. Choncho adatsata njira,
86. Mpaka pomwe adafika
Kumlowero kwa dzuwa (Ku maiko
mwaphunzitsidwa za chiongoko". Munthu uja adati: "Ndithudi, iwe suutha
kupirira nane chifukwa ine ndili ndi maphunziro anga omwe Mulungu
wandiphunzitsa, amene iwe sukuwadziwa".
Musa adati; "Undipeza ndili wopirira ngati Mulungu afuna. Sindinyoza
chilichonse cha iwe. Al-Khidhiri adati kwa iye: "Ngati unditsatedi usandifunse
kufikira nditakufotokozera". Choncho onse awiri adachoka nayenda
m'mphepete mwanyanja. Chidawadutsa chombo ndipo adawalankhula eni
chombowo kuti awanyamule. Eni chombowo adamdziwa Al Khidhiri ndipo
adawanyamula popanda malipiro . Atakwera m'chombomo Al-Khidhiri
adagulula thabwa la chombocho ndi nkhwangwa. Musa adati: "Nchiyani ichi;
anthuwa atitenga popanda malipiro ndiye ukuboola chombo chawo? Kodi
ukufuna kuti uwamize eni chombowo? Ndithudi, wachita chinthu choipa kwambiri".
Kenaka adachoka m'chombo muja nayamba kuyenda m'phepete mwanyanja.
Pompo Al-Khidhiri adaona mwana akusewera ndi mzake ndipo adamgwira
mwana uja mutu wake ndikuuzula, nkumpheratu. Musa adati kwa iye: "Bwanji
wapha munthu wosalakwa yemwe sadaphe munthu mnzake? Ndithu, wachita
chinthu chonyansa kwabasi,". Munthu uja adati; "Kodi sindidakuuze kuti sutha
kupirira nane"? Musa adati: "Ngati ndikufunsanso chinthu china pambuyo pa
ichi, usandilole kutsagana nawe. Apo tsono ndiye kuti kundidandaula kwako
kwakwanira pa ine". Tero adachoka mpaka kufika pamudzi wina. Apo
adapempha chakudya kwa eni mudziwo. Adakana kuwalandira monga
alendo. Ndipo kenaka adapeza khoma lili pafupi kugwa, Al-Khidhiri adati ndi
mkono wake "Ima chonchi" - polilozera ndi mkono wake. Ndipo lidaimadi
njoo!. Musa adati: "Ha! Anthu akuti tawadzera pamudzi, ndipo sanatipatse
chakudya sanatilandirenso ngati alendo-apatu ukadafuna ukadaitanitsa
malipiro." Munthu uja adati: "Awa ndiwo malekano a iwe ndi ine. Komabe
ndikuuza matanthauzo a zomwe sudathe kupirira nazo."
Izi ndi zina zododometsa za Mulungu zomwe amazichita kupyolera m'manja
mwa anthu Ake olungama. Ngati tidzakhala olungama ndiye kuti Mulungu
adzatipatsa mphamvu zochita zinthu zododometsa
Surat 18. Al-Kahf Juzu 16
633 > t *&\
\ A J4&1 $j^->
a kuzambwe), adaliona (ngati)
Likulowa padziwe lamatope
ambiri. Ndipo pompo adapeza
anthu; tidati, "E, iwe Zul Qarnain!
Alange, kapena Achitire zabwino."
87. Adati: "Koma amene achita
zosalungama Timulanga; ndipo
kenako adzabwezedwa Kwa Mbuye
wake; ndipo Akamukhaulitsa ndi
chilango choipa.
88. Koma amene akhulupirire
ndikuchita Ntchito zabwino, apeza
mphoto yabwino; Ndipo timuuza
zomwe zili zofewa M'zinthu zathu."
89. Kenako adatsata njira,
90. Mpaka adafika ku mtulukiro
kwa dzuwa (Kumaiko akuvuma).
Adalipeza (dzuwalo)
Likuwatulukira anthu omwe
sitidawaikire Chowatchinga ku ilo.
91. Momwemo, Tidali kudziwa
bwino Nkhani zonse zomwe zidali
ndi iye.
92. Kenako adatsata njira,
93. Mpaka pomwe adafika
pakatikati pa mapiri Awiri adapeza
pafupi Ndi mapiriwo anthu omwe
sikudali Kwapafupi kumva
chiyankhulo.
94. Adati: "E, iwe Zul-Qarnain!
Ndithu Yaajuju ndi Maajuju
akuononga padziko. Kodi
sikungatheke kuti tikupatse
$&».
Surat 18. Al-Kahf Juzu 16
634
\ *\ frji-l > A ci$&l djj~*>
Malipiro kuti uike pakati pathu ndi
Pakati pawo, chotchinga (mpanda)?
95. (lye) adati: "Zomwe Mbuye
wanga Wandipatsa ndi zabwino.
Choncho Ndithandizeni ndi
mphamvu zanu (zonse Pantchito
imeneyi) ndiika chotchinga
Cholimba pakati panu ndi pakati
pawo.
96. Ndipatseni zidutswa za
zitsulo". Kufikira pamene
adadzadza ndi zitsulozo Mpata
umene udalipo pakati pa mapiri
Awiriwo, adati: "Pemererani
(moto)". Mpaka (chitsulocho)
chidafiira monga Moto, adati:
"Ndibweretsereni mtovu
Wosungunuka ndiuthire
pamwamba pake (Pa chitsulocho)".
97. Choncho (Yaajuju ndi
Maajuju) sadathe Kukwera
pamwamba pake, ndiponso sadathe
Kuchiboola.
98. (lye) adati: "Ichi ndi chiflindo
Chochokera kwa Mbuye wanga;
koma Likadzafika lonjezo la Mbuye
wanga (Kudza kwa Kiyama),
adzachiswanyaswanya; Ndipo
lonjezo la Mbuye wanga nloona.
99. Ndipo patsiku limenelo
tidzawasiya ena Aiwo (oipa)
akuchita chipolowe pa ena; Ndipo
lidzaimbidwa lipenga Pamenepo
tidzawasonkhanitsa onse pamodzi.
< All 9 '9* }9 9 <t. '9'9 9'9'Y^'
Surat 18. AI-Kahf Juzu 16
635
n *>i
> A ci^Jl «jj-o
100. Ndipo tsiku limenelo,
tidzayionetsa Poyera Jahannama
kwa osakhulupirira.
101. (Osakhulupirira) omwe
maso awo adali Ophimbidwa
pakusalabadira ulaliki Wanga,
ndipo sadali kutha kumva (Zimene
akuuzidwa).
102. Kodi osakhulupirira
akuganiza kuti Angawasandutse
akapolo anga kukhala Atetezi
kusiya Ine? Ndithu, Taikonza
Jahannama kukhala malo
Ofikirapo osakhulupirira.
103. Nena:"Kodi tikudziwitseni
eni Kuluza (kulephera) pazochita
zawo?"
104. "I wo ndi omwe khama
lawo lataika Paumoyo wa padziko
lapansi, pomwe Iwowo akuganiza
kuti akuchitaZabwino". 1
105. Iwowo ndi amene
sadakhulupirire Zisonyezo za
mbuye wawo, ndipo
(Sadakhulupirire) zakukumana
Naye. Choncho zochita zawo
©l££ tiS^^J^*^
M'ndime iyi akutiuza kuti amene sadakhulupirire Mulungu, pa tsiku lomaliza
ndiye kuti zonse zochita zawo zidzakhala zowonongeka. Ntchito zabwino za
munthu kuti zikalandiridwe kwa Mulungu, poyamba akhulupirire Mulungu
ndiponso akhulupirire kuti tsiku lachimaliziro lilipo. Koma ngati sakhulupirira,
ndiye kuti zochita zake sizikayesedwa pasikelo koma akangomponya
kung'anjo yamoto. Pankhaniyi Mtumiki (SAW) adati, "Tsiku la Kiyama
padzabwera munthu wamtali, wakudyabwino, wakumwa zomwaimwa, koma
kwa Mulungu adzakhala wopepuka wosafanana ngakhale ndikulemera
kwaphiko la udzudzu". Hadisiyi adainena ndi Al -Hafizi m'buku la Fatuhul
Bari, Volume 8 tsamba la 324.
Surat 18. Al-Kahf Juzu 16
636
n *>i
> A i^A^il Sjj-*.
zaonongeka (Zapita pachabe),
ndipo pa tsiku La chiweruzo
sitidzawaikira sikero.
106. Zimenezo, mphoto yawo
ndi Jahannama Chifukwa cha
kusakhulupirira Kwawo, ndipo aya
Zanga ndi aneneri Anga
adazichitira chipongwe.
107. Ndithu, amene
akhulupirira Ndikumachita
zabwino, malo Awo ofikira
adzakhala Kuminda ya "Firdaus".
108. Adzakhala m'menemo
muyaya. Ndipo Sadzafuna
kuchokamo.
109. Nena:"Ngakhale nyanja
ikadakhala Inki yolembera mawu a
Mbuye wanga, nyanjayo ikadatha
mawu A Mbuye wanga asadathe,
ngakhale Tikadabweretsa nyanja
ina ndikuionjezera Pa iyo
(nyanjazo zikadatha, Mawu a
Mulungu akalipobe)".
110. Nena: "Ndithu, ine ndi
munthu Monga inu, (chosiyana
nchakuti) Ine ndikupatsidwa
chivumbulutso (Chonena kuti)
ndithu Mulungu Wanu ndi
Mulungu mmodzi Yekha. Ndipo
amene afuna kukumana ndi Mbuye
wake, achite Zochita zabwino
ndipo asaphatikizepo Aliyense pa
mapemphero a Mbuye wake".
'^iiJh'i
Ij^CilitVrly^ >\l
Surat 19. Maryam Juzu 16 637 ^ 1 *j*-*
\ \ fLjA j^
SURAT MARYAM XIX
Aya za Sura iyi nzaku Makka kupatula Aya ya 58 ndi 71.
Ndipo Surayi ikufotokoza kubadwa kwa Yahaya, mwana wa
Zakariya (A.S)
Zakariya adapempha za mwanayo atakalamba kwambiri
ndiponso mkazi wake adali chumba.
M' surayi mwatchulidwanso nkhani ya Maryam ndi kubadwa
kwa mwana wake Isa (A.S.) Ndipo yafotokozanso nkhani ya
Ibrahim momwe ankaitanira ku Umodzi wa Mulungu, ndikuti
iye adauza tate wake kuti asiye kupembedza mafano.
M' surayi atchulamonso za aneneri omwe ndi ana a
Ibrahim,monga: Ismaila ndi Isihaka. Ndipo mulinso nkhani ya
Idrisa. Kenako Chauta wafotokozanso za magulu omwe adadza
pambuyo pa aneneri; ena a iwo adali omvera pom we ena a iwo
adali onyoza.
M' surayi mwatchulidwanso kuti Janna, worn we ndi Munda
wamtendere, idzakhala mphotho ya okhulupirira. Ndipo moto
udzakhala mphotho ya osakhulupirira.
Surat 19. Maryam Juzu 16 638 ^ n *j£-
> * f.jA i ir .
Surat Maryam XIX
QWlt^JII^
M'dzina la Mulungu waChifundo
Chambiri, waChisoni.
1. Kaf-Ha-Ya- 'Ain-Sad .
2. Ichi (ndi) chikumbutso cha
chifundo cha Mbuye wako pa
kapolo Wake Zakariya,
3. Pamene adaitana Mbuye
wake, Kuitana kwa chinsinsi.
4. Adati: " E Mbuye wanga!
Ndithu, mafupa Anga afooka,
ndipo mutu wanga Wayaka
(ukung'anima) Ndi imvi; sindidali
watsoka Pokupemphani Mbuye
wanga (koma nthawi Iliyonse
ndikakupemphani
Mumandi vomereza) ]
5. "Ndipo ndithu, ine
ndikuopera abale anga (Kuononga
chipembedzo) pambuyo panga;
Ndipo mkazi wanga ndi chumba;
choncho Ndipatseni (mwana)
mlowammalo wanga Wochokera
kwa Inu,
6. Adzandilowe chokolo (pa
nzeru za Utsogoleri ndi uneneri)
ndikulowanso Ufumu wa banja la
Yakubu; Ndipo Mbuye wanga
1 Apa tanthauzo lake nkuti: "E, Mbuye wanga! Palibe pamene mudalitaya
pachabe pempho langa koma mudandizoloweza kuti ndikakupemphani
mumandipatsa zomwe ndapempha. Choncho yankhaninso pempho langali."
01
Surat 19. Maryam Juzu 16
639
n tjk-\
]*_fj* h**
ndichiteni kukhala Woyanjidwa
(ndi Inu)"
7. Adauzidwa): "E, iwe
Zakariya! Ife Tikukuuza nkhani
yabwino yakuti Ubereka mwana
dzina lake Yahaya Palibe
patsogolo pake amene Tidamutcha
dzina longa lake."
8. (Zakariya) adati: "Mbuye
wanga! Ndingapeze mwana bwanji
pomwe mkazi Wanga ndi
nkhalamba yosabereka ndipo Ine
ndafikanso paukulu wopyola
muyeso?"
9. Adati: Ndimomwemo.
Mbuye wako wanena (Kuti), "Izi
nzofewa kwa Ine; ndithu,
Ndidakulenga kale pomwe iwe
Sudali kanthu."
10. Adati: "Mbuye wanga
ndipatseni Chizindikiro
(chodziwitsa kuti mkazi Wanga ali
ndi pakati)." Adati: "Chizindikiro
chako ndikuti sudzatha Kuyankhula
ndi anthu mpaka masiku atatu
Pomwe iwe uli bwinobwino."
11. Ndipo adatuluka kuchipinda
Chopempherera ndikuonekera kwa
anthu ake Ndipo adawalozera
(pomwe Sadathe kuyankhula) kuti
lemekezani Mulungu m'mawa ndi
madzulo.
12. "E, iwe Yahaya! Gwira
Buku ili Mwamphamvu (ndi
'pMwn&a$\£<g±
Surat 19. Maryam Juzu 16 I 640 I ^ 1 *jJt-i
\ H (Cy Oj^
mwachidwi)." Ndipo tidampatsa
nzeru ali mwana.
13. Ndipo uku kudali
kuwamvera chisoni (makolo Ake)
chochokera kwa Ife ndi
Kumuyeretsa (mwanayo).
Choncho adali woopa Mulungu,
14. Komanso wochitira
zabwino makolo ake Ndipo sadali
wodzitukumula (kwa anthu)
Kapena kunyoza (Mulungu).
15. Ndipo mtendere wa
Mulungu udali Paiye kuyambira
tsiku lomwe Adabadwa ndi tsiku
lomwe adamwalira, Ndi tsiku
limene adzaukitsidwa kuimfa
Kukhala wamoyo.
16. Ndipo mtchule Maryam
m'buku Hi pamene adadzipatula
Ku anthu a kubanja lake (Ndikunka)
kumalo ambali ya kummawa. 1
17. Ndipo adadzitsekereza Kwa
iwo (kuti athe kutumikira Mulungu
Mokwanira) choncho tidatuma
Mngelo Wathu (Gabriel) kwa iye
Ndipo adadzifanizira kwa iye
Monga munthu weniweni.
^&$&'*&l$3
M'sura iyi muli nkhani zododometsa. Yoyamba njakubadwa kwa Yahaya
(Yohane) yemwe adabadwa kuchokera kwa nkhalamba ziwiri zotheratu;
pomwe mwamuna adali ndi zaka 120 ndipo mkazi adali ndi zaka 98. Choncho
kubadwa kwa Yahaya kudali kododometsa. Koma kubadwa kwa Isa (Yesu)
ndikumene kudali kododometsa zedi poti iye anabadwa kwa namwali
wosakwatiwa.Tero iye anamubereka popanda wamwamuna. Zonsezi
Mulungu adafuna kuwadziwitsa anthu ndi kuwatsimikizira kuti lye ali ndi
mphamvu zolengera munthu popanda mwamuna.
Siirat 19. Maryam Juzu 16
641
n ^jA-t
1 ^ £.j* 5j>-
&
U<Wi
&
3WjlA<JP*~+1
18. (Maryam) adati: "Ndithu,
ndikudzichinjirizaNdi Mulungu
Mwini chifundo chambiri, kwa
Iwe ngati umaopa Mulungu."
19. (Mngelo) adati: "Ndithu, ine
ndine Mtumiki wa mbuye wako,
(ndadza) Kuti ndikupatse mwana
woyera."
20. Adati: "Ndingakhale bwanji
ndi mwana pomwe Sadandikhudze
mwamuna (aliyense), ndipo Ine
sindili (mkazi) wachiwerewere?"
21. (Mngelo) adati;"Ndi
momwemo"Mbuye Wako akuti:
"Zimenezi kwa Ine nzosavuta.
Ndipo timchita kukhala
chozizwitsa Kwa anthu ndi
mtendere Wochokera kwa Ife.
(Nchifukwa chake Tachita izi;)
ndipo ichi ndi chinthu Chimene
chidalamulidwa kale, (chichitika
Monga momwe Mulungu
adafunira)."
22. Choncho adatenga pakati
pake, Ndipo adachoka ndi pakatipo
kunka Kumalo akutali. 1
23. Ndipo matenda auchembere
(atakwana), Adampititsa kuthunthu
lamtengo wa Kanjedza (wouma
kuti awutsamire pomubala
1 Izi zidachitika pamene Gabriel adauzira m'thumba la chovala cha Maryam.
Ndipo mpweya udafika mpaka m'mimba mwake. Choncho atakhala ndi pakati
anadzipatula kwa anthu kunka kutali ali ndi pakati pamwana wakeyo kuti
anthu angamdzudzule pokhala ndi mimba yosadziwika mwamuna wake.
®4^fc^S&\tfs«
Surat 19. Maryam Juzu 16 I 642 I ^ n *jJH
> S f_y 5jj--
Mwanayo) adati: "Kalanga ine!
Ndiponi Ndikadafa izi
zisanachitike Ndikadakhala
nditaiwalidwa, ndithu."
24, Kenaka (Mngelo)
adamuitana kuchokera Chapansi
pake (kumuuza kuti):
"Usadandaule. Ndithu, Mbuye
wako Wakupangira kamtsinje
pansi pako;
25, Ndipo ligwedezere kumbali
yako thunthu Lamtengo
(woumawo). Zipatso zabwino
Zakupsa zikugwera. 1
26, Choncho udye ndi kumwa
ndikutonthoza Diso lako, (khala
ndi mpumulo wabwino). Ndipo
ukaona munthu aliyense (akafunsa
Za mwanayo), nena: "Ndithu, ine
ndalonjeza Kwa (Mulungu) Mwini
chifundo chambiri Kumanga kuti
lero sindiyankhula ndi Munthu
aliyense."
27, Ndipo adadza naye
(mwanayo) kwa anthu Ake
atamnyamula. (Anthu)adati: "E,
Iwe Maryam! Ndithu, wabwera ndi
chinthu Chachikulu;
(chododometsa)";
®V
*»*.*-*
1 Omasulira adati: Adamulamula kuti agwedeze thunthu lamtengo wouma kuti
aone chizizwa chachiwiri mtengo wouma pokhala wauwisi ndikubereka
zipatso nthawi yomweyo zakupsa. Adamuonetsanso kasupe wamadzi okoma
yemwe anafwamphuka uku iye akuona. Ndipo iye adali kudya zipatsozo
nkumamwera madziwo. Uku kudali kumulimbikitsa mtima kuti asade nkhawa
pokhala ndi mwana wdpanda tate wake koma zonsezi wazichita ndi Mulungu.
Surat 19. Maryam Juzu 16
643
n *>»
^ * fs 5 jj-*
28. "E, iwe mlongo wa
Haaruna! Bambo wako Sadali
munthu woipa, ngakhalenso mayi
Wako sadali wachi were were." 1
29. (Maryam sadawayankhe)
koma adaloza kwa iye (Mwanayo
kuti ayankhule naye). Ndipo iwo
Adati: "Timuyankhula chotani
mwana yemwe ali m'chikuta?"
30. (Mwanayo) adanena: "Ine
ndine kapolo wa Mulungu.
Wandipatsa Buku ndikundichita
Kukhala Mneneri;
31. Ndipo wandichita kukhala
Wodala paliponse pomwe ndili,
Ndipo wandilamula kuswali ndi
Kupereka Zakat pomwe ndili moyo.
32. Ndipo wandilangiza
kuchitira mayi Wanga zabwino,
ndipo sadandichite Kukhala
wodzikuza, (woipa) watsoka;
33. Ndipo mtendere uli pa ine
kuyambira Tsiku lomwe
ndidabadwa ndi tsiku Limene
ndidzamwalira, ndi tsiku limene
Ndidzaukitsidwa (kwa akufa tsiku
lachiweruzo) Ndikukhala ndi moyo."
34. Uyu ndi Isa (Yesu) mwana
wa Maryam: (Awa ndi) mau
mi
&Cfi&&\&<&
1 Katada adaati: Haaruna adali munthu wolungama kwambiri mumtundu wa
Ana alsraeli. Adalj wotchuka kwambiri pazakulungama. Choncho Ana alsraeli
adali kufanizira Maryam ndi Haaruna chifukwa cha kulungama kwake; sikuti
Maryam adali mlongo wake weniweni wa Haaruna yemwe adali m'bale wa
Musa. Pakati pa Maryam ndi Haaruna padapita zaka chikwi chimodzi.
Surat 19. Maryam Juzu 16
644
n *>»
y^f^hj-*
owoona omwe (Akhrisitu)
Akuwakaikira.
35. Sikoyenera kwa Mulungu
kudzipangira Mwana. lye
(Mulungu) wapatukana ndi
Zimenezi. Akafuna chinthu,
amangonena Kwa chinthucho
"chitika," ndipo icho Chimachitikadi.
36. (Yesu adati:) "Ndipo ndithu,
Mulungu ndi Mbuye wanga
ndiponso Mbuye wanu. Choncho
mpembedzeni; iyi njira yolunjika
(Yokufikitsani ku mtendere.) 1
37. Koma magulu (a Akhrisitu
ndi Ayuda) Adapatukana pakati
pawo; (ena adamuyesa Yesu kuti
ndimwana wa Mulungu, ndipo Ena
adamuyesa Mulungu weniweni
pomwe Ayuda ankati ndi mwana
wobadwa M' njira ya chi were were)
choncho chilango Chaukali
chidzatsimikizika pa amene
Sadakhulupirire pokaonekera tsiku
Lalikululo (kwa Mulungu).
38. Taona kumvetsetsa kwawo
Ndikupenyetsetsa kwawo Tsiku
lodzatidzera, (kudzanenedwa kuti:)
"Koma osalungama lero ali
m'kusokera koonekera".
1 Umu ndimomwe Yesu adanenera za ukapolo wake kwa Mulungu. lye sadali
Mulungu kapena mwana wa Mulungu, kapena mmodzi wa atatu monga
momwe Akhrisitu amanenera. Koma iye adali kapolo wa Mulungu ndiponso
Mtumiki wake. Chauta adamulenga mwa mayi popanda bambo kuti akhale
chisonyezo chosonyeza mphamvu za Mulungu zoposa.
Surat 19. Maryam Juzu 16 645 * 1 *j^
n
f-j* *jj~>
39. Ndipo achenjeze (anthu) za
tsiku la Madandaulo, pamene
chiweruzo chidzagamulidwa,
(Abwino kulowa ku munda
wamtendere, Oipa kulowa ku
moto); koma iwo(pano Padziko
lapansi) ali m'kusalabadira Ndipo
sakhulupirira. l
40. Ndithu, Ife Tidzaitenga
nthaka ndi Amene ali pamenepo;
(zonse zidzakhala za Ife) Ndipo
kwa Ife adzabwezedwa.
41. Ndipo mtchule m'buku ili,
Ibrahim. Ndithu, iye adali wonena
zoona Zokhazokha, Mneneri.
42. (Akumbutse) pamene iye
adauza bambo wake: "E, inu
bambo wanga! Bwanji
mukupembedza Zomwe sizimva
ndiponso sizipenya, ndiponso
Zosakupindulitsani chilichonse?"
1 Tsiku la Kiyama (chimaliziro), anthu oipa adzadandaula kwambiri. Tsiku
limenelo kwa iwo lidzakhala tsiku lamadandaulo okhaokha, osatinso
chinachake.M'buku la swahihi la Musilimu muli hadisi ya Abi Saidi Khuduriyi.
lye adati: Ndithu, Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale ndi iye) adati,
"Pamene anthu olungama adzalowa kumunda wamtendere ndipo anthu oipa
kumoto, imfa idzadza tsiku la chimalizirolo. Idzaoneka ngati nkhosa yabwino.
Ndipo idzaikidwa pakati pamunda wamtendere ndi moto. Tsono
kudzanenedwa, "E, inu eni munda wamtendere! Kodi ichi
mukuchidziwa?"Onse adzatukula makosi kuyang'ana nkuzati: "Inde iyo ndi
imfa." Kenako kudzanenedwa: "E inu anthu akumoto kodi ichi mukuchidziwa?"
Onse adzatukula makosi awo kuyang'ana nkuzati: "Inde iyo ndi imfa." Ndipo
kudzalamulidwa kuti izingidwe. Kenako kudzanenedwa: "E, inu eni munda
wamtendere! Khalani muyaya m'menemo, palibe imfanso. Ndiponso inu eni
moto khalani muyaya mmenemo palibe imfanso. "Kenako Mtumiki (madalitso
ndi mtendere zikhale naye) adawerenga aya (ndime) yakuti: "Achenjeze
zatsiku lamadandaulo aakulu".
Surat 19. Maryam Juzu 16 I 645 I \ *\ *j*-i
H
f j* •j>*
43. "E, inu bambo wanga!
Ndithu, ine Zandidzera nzeru
(zomuzindikira Mulungu) Zomwe
sizidakudzereni; choncho
nditsateni. Ndikutsogolereni
kunjira yolungama.
44. E, bambo wanga!
Musapembedze satana (Potsatira
malangizo ake). Ndithu, satana
Ngopandukira (Mulungu) Mwini
Chifundo Chambiri.
45. E, bambo wanga! Ndithu,
ine ndikuopa kuti Chilango
chingakukhudzeni chochokera
Kwa (Mulungu) Mwini chifundo
chambiri, Ndipo potero mdzakhala
bwenzi la satana."
46. (Bambo wake) adati: "Kodi
iwe ukuda Milungu yanga, E, iwe
Ibrahim? Ngati susiya (kunyoza
milungu yanga) Ndikugenda ndi
miyala; choncho ndichokere Kwa
nthawi yaitali (tisaonanenso)."
47. (Ibrahim) adati: "Mtendere
ukhale pa inu! Ndikupempherani
chikhululuko kwa Mbuye Wanga
(ngakhale mwandipirikitsa).
Ndithu, iye amandichitira chisoni
kwambiri.
48. "Ndipo ine ndikupatukirani
ku zomwe Mukuzipembedzazo
kusiya Mulungu Ndipo ndipempha
Mbuye wanga; ndithu Sindikhala
watsoka popempha Mbuye wanga".
$&%&&£$&»
$&$&£&&!
Surat 19. Maryam Juzu 16
647
n *>»
^ * f-S b**
49. Ndipo pamene
adawapatukira ndi zimene adali
Kuzipembedza kusiya Mulungu,
tidampatsa iye Isihaka, ndi
Yakubu, ndipo aliyense wa iwo
Tidampanga kukhala M'neneri.
50. Ndipo tidawapatsa iwo
chifundo Chathu, Ndi kuwayikira
iwo kutchulidwa kwabwino,
Kwapamwamba (pakati
pazolengedwa).
51. Ndipo mtchule Musa
M'buku (ili) Ndithu, iye adali
wosankhidwa ndi Woyeretsedwa:
ndipo adali Mtumiki M'neneri.
52. Ndipo tidamuitana kumbali
yakudzanjadzanja La phiri la Turi,
ndipo tidamuyandikitsa ndi
Kuyankhula Nafe
momunong'oneza.
53. Ndipo mwachifundo Chathu
tidampatsa (Musa) M'bale
wake Haaruna kukhala mneneri
(Womuthangata)
54. Mtchulenso M'buku (ili)
Ismaila; ndithu, Iye adali woona
palonjezo, ndipo adali Mtumiki
Mneneri.
55. Adali kulamula anthu ake
swala ndi Zakat, ndipo kwa mbuye
wake adali Woyanjidwa.
56. Mtchulenso M'buku (ili)
Idirisa, Ndithu, iye adali wonena
Zoona zokhazokha, Mneneri.
©^c|o*e
r^ IV <Jty S 9
Surat 19. Maryam Juzu 16 648 ^ *i *j*-'
S <\ f mJ A 5j^
57. Ndipo tidamuika malo
Apamwamba.
58. Iwowo ndi omwe
adawadalitsa Mulungu, mwa
aneneri mu ana a Adam, Ndi
(m'mbumba ya) amene
tidawatenga pamodzi ndi Nuhi
(m'chombo), Ndi m'mbumba ya
Ibrahim ndi Israeli Ndi amene
tidawaongola ndi kuwasankha.
Ndipo zikawerengedwa kwa iwo
aya za (Mulungu) Mwini chifundo
chambiri, Amagwa ndi kulambira
uku akulira.
59. Koma pambuyo pa iwo
padadza anthu oipa. Adasokoneza
swala (adasiya kupemphera)
Natsatira zilakolako zoipa; Choncho
adzakumana ndi chilango choipa.
60. Kupatula amene ati alape
ndikukhulupirira Ndikuchita
zabwino; iwowo adzalowa ku
Munda wa mtendere ndipo
sadzachitidwa Chinyengo pa
chilichonse.
61. Munda wamuyaya umene
(Mulungu) Wachifundo chambiri
Walonjeza akapolo Ake Mobisika
ndithu lonjezo Lake ndilakudza.
62. Sakamva m'menemo mawu
achibwana, Koma mawu
amtendere; ndipo akapeza Riziki
(chakudya) lawo m'menemo
M'mawa ndi madzulo.
< "*&'.
Surat 19. Maryam Juzu 16 649 > 1 pjk-
\ * f.jA *jj~>
63. Umenewo ndiwo munda
wamtendere umene Tikawapatsa
ena mwa akapolo athu omwe Adali
oopa Mulungu.
64. (Mtumiki adapempha
Gabriel kuti akhale Akum'bwerera
pafupipafupi. Ndipo Gabriel
adamuuza kuti): "Ndipo
sitimatsika Koma mwalamulo la
Mbuye wako. Zapatsogolo pathu
ndi zapambuyo pathu Ndi zapakati
pazimenezi zonse Nzake
(akuzidziwa bwinobwino). Ndipo
Mbuye wako sali Woiwala.
65. Mbuye wa thambo ndi
nthaka ndi zapakati Paizo:
Choncho mpembedze iye basi.
Ndipo pitiriza ndikupirira
Popembedza Iye. Kodi
ukumudziwa (Wina) yemwe ali
Wofanana naye (Mulungu)?"
66. Ndipo munthu (wokanira)
amanena: "Kodi ndikadzafa
nzoonadi kuti Ndidzatulutsidwa
(m'manda) Nkukhala wamoyo?."
67. Kodi munthu sakumbukira
kuti Tidamulenga kale pomwe
sadali Chilichonse?
68. Choncho ndikulumbira
Mbuye wako ndithu,
Tidzawasonkhanitsa iwo pamodzi
ndi Asatana; ndipo tidzawafikitsa
m'mphepete Mwa Jahannama uku
atagwada.
(±^v^fy?QC^\ $&}
Surat 19. Maryam Juzu 16
650
n *>•»
) * fljA 5j^
69. Kenako, m'gulu lililonse
tidzachotsamo Yemwe adali
wopyola malire polakwira
(Mulungu) Mwini chifundo
chambiri.
70. Ndipo Ife tikuwazindikira
kwambiri Amene ali oyenera
kulowa M'moto.
71. Ndipo palibe aliyense mwa
inu Koma adzaifika
(Jahannamayo). Ndithu Hi ndi
lamulo la Mbuye wako lomwe
Lidalamulidwa kale.
72. Ndipo kenako
tidzawapulumutsa amene Ankaopa
Mulungu ndipo osalungama
Tidzawasiya m'menemo atagwada.
73. Ndipo aya Zathu zomveka
bwino zikawerengedwa kwa iwo,
omwe sadakhulupirire Amanena
kwa omwe akhulupirira: "Ndi gulu
liti pamagulu awiri awa, (Lanu ndi
lathu) lomwe lili ndi pokhala
Pabwino ndikukhalanso ndi anthu
Olemekezeka?"
74. Ndipo mibadwo yambiri
tidaiononga Patsogolo pawo,
Yomwe idali ndi ziwiya Zabwino
ndi maonekedwe abwino.
75. Nena: "Amene ali
mkusokera, (Mulungu) Mwini
chifundo chambiri amuonjezera
Nthawi yamoyo kufikira azione
^i^teawffigj
Surat 19. Maryam Juzu 16 I 651 I \ *\ t$?\
\ \ fijA S j>*>
zomwe Akulonjezedwa- kapena
chilango Kapena kudza nthawi (ya
Kiyama) Pamenepo ndipomwe
adzadziwa kuti Ndani mwini
kukhala pamalo poipa, ndi Mwini
wa ankhondo ofooka (Iwo kapena
Asilamu)?"
76. Ndipo Mulungu
amawaonjezera chiongoko Amene
aongoka. Ndipo zochita zabwino
Zonkerankera (mpaka tsiku
Lachimaliziro), ndizo zili zabwino
Kwa Mbuye wako monga mphoto,
Ndiponso ndiko kobwerera
kwabwino, (Osati zamdziko Zomwe
anthu osalungama akunyadira).
77. Kodi wamuona yemwe
watsutsa aya Zathu Ndikunena
kuti: "Ndithu, Ndidzapatsidwa
chuma ndi ana (pa tsiku
Lachimaliziro monga momwe
andipatsira Pano padziko?)"
78. Kodi adapenya zamseri,
kapena adalandira Lonjezo kwa
Mulungu mwini chifimdo Chambiri
(kotero kuti ali ndi chikhulupiriro
Pazimene akunenazo)?.
79. Sichoncho,ndithu tikulemba
zonse zomwe Akunena, ndipo
tidzamuonjezera nyengo Yotalika
m' chilango.
80. Ndipo tidzamlowa mmalo
zimene akunenazi, (Chuma ndi
anawo), nadzatidzera Ali
0l,
Surat 19. Mary am Juzu 16
652
n *>i
^ * fljA Sj^rf
yekhayekha (wopanda chuma ndi
Zonse zomwe ankanyadira).
81. Eti adzipangira milungu ina
m'malo Mwa Mulungu kuti
milunguyo iwapatse Mphamvu
(ndi ulemerero).
82. Iyayi! Idzawakanira
Mapemphero awo Ndikuwaukira.
83. Kodi suona kuti Ife
timawatuma Asatana kwa
osakhulupirira ndipo
Akuwakhwirizira kwambiri
(kuchita Zoipa)?
84. Choncho, usawachitire
changu (kuti Alangidwe tsopano),
ndithu, Ife Tikuwawerengera
chiwerengero (cha Masiku awo;
masiku akakwana, Tiwalanga.)
85. (Kumbukira iwe Mtumiki)
tsiku lomwe Tidzawasonkhanitsa
oopa (Mulungu) Kunka nawo
kumunda wa Mwini chifundo
Chambiri ali m'magulumagulu
monga Nthumwi zake (kuti
apatsidwe ulemu.)
86. Ndipo oipa tidzawakusa
kunka nawo Ku moto uku ali ndi
ludzu lalikulu. (Monga momwe
ziweto zimathamangira Kupita
kumadzi zikakhala ndi ludzu
Lalikulu).
87. Sazakhala ndi mphamvu
yoombolera (ena) Koma kupatula
;ffli©^S&!332S
2Jb
^
txpmt&s&
^^>jia«ss
A\*' '1"" H| '* »f\L*X€
<&ffi^X&&&$
Surat 19. Maryam Juzu 16
653
n *>-i
)%
f-j> hf
omwe adagwiritsa lonjezo la
(Mulungu) Mwini chifundo
chambiri.
88. Ndipo (osakhulupirira
omwe ndi Ayuda ndi Akhirisitu)
akuti "(Mulungu) Mwini chifundo
chambiri Wadzipangira Mwana!"
89. Ndithu, mwadza ndi chinthu
choipitsitsa Kwambiri (pazimene
mukunenazi).
90. Thambo layandikira
Kusweka ndi mawuwo, Ndipo
nthaka kuphwasuka, ndipo mapiri
Kugwa ndikudukaduka.
91. Chifukwa chakumunamizira
(Mulungu) Mwini chifundo
chambiri kuti ali ndi Mwana.
92. Ndipo nkosayenera kwa
(Mulungu) Mwini Chifundo
chambiri kudzipangira mwana.
93. Palibe aliyense yemwe ali
kumwamba ndi Pansi koma
adzadza kwa (Mulungu) Mwini
Chifundo chambiri ali kapolo
(Wake).
94. Ndithu (Mulungu)
wawadziwa mokwanira Ndipo
adzawawerenga aliyense
Payekhapayekha.
95. Ndipo, aliyense wa iwo
adzadza kwa lye (Mulungu) ali
payekhapayekha
s«^i
w&&@&&
M^.'SLs?
*< 9 .C'?> '9titff> "W&
Surat 19. Maryam Juzu 16
654
n ^jA-i
^ ^ f.y 6j**
96. Ndithu amene akhulupirira
Ndi kumachita zabwino,
(Mulungu) Mwini chifundo
Chambiri adzaika chikondi Pakati
pawo.
97. Ndithu, taifewetsa (Qur'an)
M'chiyankhulo chako kuti ndi iyo
Uwawuze nkhani zabwino oopa
Mulungu ndipo ndi iyo
uwachenjeze Anthu amakani.
98. Kodi ndi mibadwo ingati
tidaiononga Patsogolo pawo? Kodi
ukumuona Mmodzi wa iwo,
kapena ukumva Mgugu wawo?
Surat 20. Ta-Ha Juzu 16 655 ^ *j*-» t • & i^
Sura iyi idavumbulutsidwa ku Makka kupatula aya ziwiri
zomwe ndi aya ya 130 ndi 131. Sura iyi yayamba ndi malembo
awiri omwe akusonyeza kuti Qur'an njachidule ndi yomveka.
Ndipo pambuyo pa malembo awiri, Surayi yafotokoza za
Ulemerero wa Qur'an ndi kutukuka kwa Yemwe adaivumbulutsa,
yemwe ndi Mulungu Woyera, Mwini thambo ndi nthaka;
Wodziwa zobisika zonse.
Surayi yafotokozanso nkhani ya Musa ndi Farawo ndi
momwe utumiki wa Musa udayambira. Ndikutinso iye (Musa)
adapempha Mulungu kuti asankhe Haaruna kukhala mthandizi
wake. Ndipo yafotokozanso momwe Musa, Haaruna ndi Farawo
adakumanirana pomwe adali kuopa kukumana naye chifukwa
chakuipa mtima kwake ndi nkhanza zake. Ndipo Mulungu
wafotokozanso momwe Musa (A.S) adaleredwera.
M' surayi mulinso za momwe Musa ndi Farawo
ankabwezerana mawu ndi pakati pa Musa ndi amatsenga, ndi
mantha a Musa ngati amatsenga atapambana. Ndipo mulinso
mawu oti pomwe Musa adaponya ndodo yake, idameza zingwe
za amatsenga zomwe zimaoneka ngati njoka. Ndipo
yafotokonzanso mathero a zochitachita za amatsenga, kuti iwo
adakhulupirira ndipo Farawo adawalanga chifukwa cha
kumkhulupirira Musa.
Surayi yafotokozanso zakupulumuka kwa Musa ndi ana a
Isiraeli kuchiwembu cha Farawo ndi momwe Farawo
adamizidwira m'madzi. Izi zidachitika pamene Musa
adamenyetsa ndodo panyanja ndipo madzi adagawikana, iwo
nkulowapo. Ndipo naye Farawo adatsatira.
Surayi yatinso pamene Musa adaoloka, adaitanidwa kuphiri
ndi Mulungu kuti akanene naye. Ndipo iye atapita kuphiri,
Samiriyu adawasokoneza ana a Israeli powalangiza
Surat 20. Ta-Ha
Juzu 16
656
n *>i
Y * <& Sjj-*»
zakupembedza mwana wa ng'ombe wopangidwa ndi golide.
Pazomwe zidachitikazi, Musa adakwiya kwambiri kotero kuti
adagwira mutu wa mbale wake Haaruna ndi kumaukoka.
Komanso surayi yafotokoza za chilango chomwe chidampeza
Samiriyu. Ndipo Mulungu wasonyeza phunziro lomwe lili
m'nkhani ya Musa ndi aneneri ena. Ndipo kumalekezero kwa
surayi kuli malangizo a kupirira, kupewa makhalidwe oipa
ndikufunika kwa swala.
Kothera kwenikweni Surayi yalongosola za chilango chomwe
osakhulupirira adzalandira, ndi mtendere womwe anthu abwino
adzapeza.
Surat 20. Ta-Ha
Juzu 16
657 1 1 *>»
Y • *k 5jj-*»
Swraf 7a-Jfa AST
M'dzina la Mulungu waChifundo
Chambiri, waChisonl
\.Ta-Ha x
2. Sitidakuvumbulutsire iwe
Qur'an kuti Uvutike nayo,
3. Koma kuti ikhale ulaliki ndi
chikumbutso Kwa yemwe akuopa
(ndikudzichepetsa Kwa Mulungu).
4. Chovumbulitsidwa
chochokera kwa Yemwe adalenga
nthaka ndi thambo Lotukuka
kumwamba.
5. (lye ndi Mulungu),Wa
chifundo Chambiri; pampando
wachifumu Adakhazikika,
(kukhazikika Koyenerana ndi
ulemerero Wake Kopanda
kukufanizira ndi kukhazikika Kwa
chilichonse; pakuti lye salingana
Ndi chilichonse pachikhalidwe ndi
Mbiri zake).
6. Zonse zakumwamba ndi
zapansi ndi Zapakati pake ndi
zapansi Pa nthaka, nza lye.
o^l^fcfcW-
-^
Mulungu wapamwamba wayamba Sura iyi ndi malembo awa awiri
potchalenja omwe akutsutsa zoti Qur'an idachokera kwa Mulungu, kuti
atalemba yawo Qur'an yomwe malembo ake omwewa omwe iwo akuwadziwa
bwino ndipo amawayankhula.
Koma alephera kutalitali kulemba Buku ndi nzeru zawo monga ili. Ndipo
kulephera kwawo kulemba Buku longa ili, ndiumboni kuti Bukuli lidachokera
kwa Mulungu.
Surat 20. Ta-Ha
Juzu 16
658
vn *>»
t% &
•j>*
7. Ndipo ngati ulankhula
mokweza mawu, (Iwe munthu),
ndithu, lye akudziwa Zobisika ndi
zobisika kwambiri Kwambiri
(mwazibisa mumtima mwanu). 1
8. Mulungu! Palibe
wopembedzedwa Mwachoonadi
koma lye. lye ali Ndi maina
abwino (ndi mbiri zabwinonso).
9. Ndipo kodi yakufika nkhani
ya Musa? (Yomwe njododometsa)? 2
10. Pamene adaona moto
adauza banja lake: "Yembekezani
(pano); ndithu, ndaona moto;
Mwina ndingakakutengereni
chikuni chamoto (Kuti muothe),
kapena ndikapeza Ondiongolera
njira pamotopo.
11. Koma pamene adaudzera
motowo Anaitanidwa (kuti), "E,
iwe Musa!
12. Ndithu, ine ndine mbuye
wako! Vula Nsapato zakozo;
*u&&Z£&&yi
^
V;j&yy%&
,OV«38e03?tt««3B«S3l
1 M'ndime iyi Chauta akuuza munthu kuti lye akudziwa zonse zimene munthu
amayankhula mokweza mawu ndi zimene munthu amayankhula ndi anzake
mobisa, ngakhalenso zomwe mtima wake umamnong'oneza.
2 fbun Abbas adati: "Izi zidali choncho Mussa pamene adakwaniritsa
chipangano cha nthawi imene adapangana ndi m'neneri Shuaibu chakuti
amuwetere mbuzi kwa zaka 8 kapena 10, adachoka ulendo kubwerera kwawo
ku tguputo pamodzi ndi banja lake; ndipo adasokera njira. Udali usiku
wamdima wozizira. Adayesa kupekesa moto kuti awothe koma adalephera.
Ndipo ali choncho, adangoona moto chapatali kumbali yakumanja kwa njira.
Pamene adauona adauganizira kuti ndi moto weniweni, pomwe udali moto
woyera wakuunika kwa Mulungu. Udali kuyaka mumtengo wamasamba
obiriwira. Ndipo adangomva Mbuye wake akumuitana: "E, iwe Musa! Ine
ndine Mbuye wako. Ndikukuyankhula; vula nsapato zako."
Surat 20. Ta-Ha
Juzu 16
659
U *>i
Y * de <*JJ-**
ndithu, iwe uli Pa chigwa
chopatulika, chotchedwa Tuwa.
13. Ndipo Ine ndakusankha
(kuti ukhale Mtumiki); choncho
mvera zonse Zomwe
zikuvumbulutsidwa (kwa iwe).
14. Ndithu, Ine ndine Mulungu
palibe Wopembedzedwa
mwachoonadi koma Ine; choncho
ndipembeze, pemphera Swala
moyenera pondikumbukira.
15. Ndithu, nthawi ya tsiku
lachimaliziro Idza; (choncho
Ikonzekere ndi ntchito Zabwino);
ndikuibisa dala (Kwa anthu) kuti
mzimu Uliwonse udzalipidwe
zimeneudachita. 1
16. Ndipo asakutsekereze
(kukhulupirira) Zimenezo yemwe
saikhulupirira (Kiyamayo), ndipo
akungotsata Zilakolako za mtima
wake; kuopakuti
Ungadzaonongeke".
17. "Kodi nchiyani icho chili
kudzanja Lako ladzanjadzanja, iwe
Musa?"
«&$&S$$&
1 Womasulira Qur'an adati cholinga chakubisa kudza kwa tsiku la chimaliziro,
ndi nthawi ya imfa ya munthu ndikuti Mulungu wapamwambamwamba
adalamula kuti sangavomereze kulapa tsiku la chimaliziro litadza, ndi nthawi
ya imfa itamufikira munthu. Anthu akadadziwa nthawi yeniyeni ya chimaliziro
ndi nthawi yakudza kwa imfa yawo, akadakhala akuchita zinthu zoyipa
naakhala ndi chiyembekezero choti adzalapa nthawi ikayandikira,
nadzapulumuka kuchilango cha Mulungu. Koma Mulungu anabisa zimenezo
kuti anthu akhale tcheru nthawi zonse ndikukhala okonzekera za imfa ndi za
tsiku la chimaliziro kuti zingawadzere modzidzimutsa.
Surat 20. Ta-Ha
Juzu 16
660
>n *jA-»
Y * 4^ djj-*
18. (Musa) adati: "Iyi ndi ndodo
yanga, Ndimaitsamira (poyenda)
ndi kuphopholera Masamba
ambuzi zanga; ndiponso
(M'ndodomo) muli zina
zondithandiza." 1
19. (Mulungu) adati: "Iponye
iwe Musa!"
20. Ndipo adaiponya; pompo
idasanduka Njoka yoyenda
mothamanga.
21. (Mulungu) adati: "Igwire,
usaope. Tiibwezera m'chikhalidwe
chake Choyamba.
22. Ndipo lipane dzanja lako
m'khwapa mwako Lituluka lili
loyera (ngati kuwala Kwadzuwa
ndi mwezi). Osati mwamatenda,
(Ichi chikhala) chozizwitsa china, 3
23. Kuti tikusonyeze zina mwa
zozizwitsa zathu, Zazikuluzikulu.
24. Pita kwa Farawo, ndithu,
iye wapyola Malire."
1 Womasulira adati yankho lakuti "Iyi ndi ndodo yanga" lidati yankho lokwana.
Koma iye adaonjezera payankho mawu ena amene sadamufunse chifukwa
chakuti pomwe adalipo padali pamalo poyenera kutambasuia mawu pakuti
Mulungu ndiye adali kuyankhula naye popanda mkhalapakati. Uku kudali kuti
amve kukoma koyankhulana ndi Mulungu. Pajatu mawu a wokondedwa
amatonthoza moyo ndipo amachotsa kutopa kwa mtundu uliwonse.
2 Ibun Abbas adati ndodoyi idasanduka chinjoka chachimuna chomwe chidali
kumeza miyala ndi mitengo. Pamene Musa adachiona chikumeza chilichonse
adachiopa. Nkhaniyi ikupezeka m'buku la kurutubi, volume 11, tsamba la 190.
3 Ibun Kathiri adati Musa ankati akalilowetsa dzanjalo mkhwapa mwake
kenako nkulitulutsa, limatuluka tili kung'anima ngati chipande chamwezi
popanda chonyansa chilichonse. Ichi chidali china mwa zozizwitsa zake.
Surat 20. Ta-Ha
Juzu 16
661
>n *yk\
r • A
d j>-
25. (Musa) adati: "E, Mbuye
wanga! Nditsakulireni chifuwa
changa;
26. Ndi kundifewetsera ntchito
yangayi (Imene mwandipatsa kuti
uthengawu Ndikaufalitse m'njira
yoyenera);
27. Ndipo masulani mfundo
yomwe Hi kulirime kwanga,
(ndimasulireni Kumangika kwa
lirime langa kuti Mawu anga
akakhale opanda chibwibwi). 1
28. Kuti (anthu) akamvetse
mawu anga.
29. Ndipo ndipatseni mthandizi
Wochokera kubanja langa,
30. M'bale wanga Haaruna
(Kuti akhale nduna yanga);
31. Limbitsani nyonga zanga
ndi iye,
32. Ndipo mphatikeni kuntchito
Yangayi,
33. Kuti tikulemekezeni
kwambiri.
®<^a#^$
?>&\ ■>«'.'
W\\'\>l':.'il Viiir
twd^soSs-O^-li
©'l't£££
Musa adali wachibwibwi koma chibwibwi chake sichinali chachibadwa.
Kuyamba kwa chibwibwi chake kudali motere: Kumayambiriro amoyo wake
adali kukhala m'nyumba ya Farawo. Ndipo nthawi ina Farawo adamuika
pamiyendo yake iye ali mwana. Musa adakoka ndevu za Farawo ndi dzanja
lake. Ndipo Farawo adakwiya natsimikiza zomupha. Ndipo Asiya, mkazi wake,
adati kwa iye."lyeyu sazindikira. Ndipo ndikusonyeza zimenezo kuti
udziwe.Yandikitsani kwa iye makala awiri ndi ngale ziwiri. Ngati atola ngalezo
ndiye kuti akuzindikira. Koma akatola khala lamoto, apo uzindikira kuti ameneyu
sazindikira kanthu. Choncho Farawo adamuyandikizira zonsezo ndipo iye
adatola khala lamoto nkuliponya mkamwa mwake. Potero palirime lake padali
kachipsera. Nkhaniyi ikupezeka m'buku la Tabariyi, volume 16 tsamba 159.
Surat 20. Ta-Ha
Juzu 16
662
n *>»
Y * Ae °JJ~ 1 '
34. Ndi kukutamandani
kwabasi.
35. Ndithu inu (nthawi zonse)
mumationa (Ndi kutisunga)."
36. (Mulungu) adati: "Ndithu
wapatsidwa Zomwe wapempha, E,
iwe Musa
37. Ndipo ndithu, tidakuchitira
ubwino Nthawi ina (popanda iwe
kutipempha),
38. Pamena mayi wako
tidamuzindikiritsa Zimene
tidamzindikiritsa (kuti azichite).
39. (Kuti): "Mponye
(mwanayo) m'bokosi Ndipo ponya
bokosilo mu m'tsinje; Ndipo
m'tsinje umponya m'mbali kuti
Amtenge mdani wanga ndi mdani
wake (Ndi kuti aleredwe
mwaubwino ndi Farawo); ndipo
ndidaika kukondeka Pa iwe
kochokera kwa Ine (kuti ukhale
Wokondedwa ndi anthu onse)
ndikuti Uleredwe
moyang'aniridwa ndi Ine".
40. (Kumbuka) pomwe mlongo
wako Ankayenda (kunka kubanja
la Farawo) Ndipo adati: "Kodi
ndikulondolereni Munthu amene
angathe kumlera?" Ndipo
Tidakubwezera kwa mayi wako
kuti maso Ake atonthole, ndipo
asadandaule. Ndipo Kenaka
®mzm
®
<>j&^3i&»i
<3i£a& S *?& d&s& ti
Surat 20. Ta-Ha
Juzu 16
663
n *>»
Y * aIp *jj~*
udapha munthu (mwangozi), ndipo
Tidakupulumutsa kumadandaulo;
Tidakuyesa ndi mayeso ambiri.
Udakhala zaka zambiri ndi anthu a
ku Madiyani. Kenaka wabwera
(apa) monga Mwachikonzero, ee,
Iwe Musa! l
41. Ndipo ndakusankha ndekha
(kuti ukhale Mtumiki Wanga).
42. Pita iwe ndi mbale wako ndi
Zozizwitsa zanga, ndipo musatope
(Musasiye) kundikumbukira.
43. Pitani kwa Farawo, ndithu,
iye Wapyola malire.
44. Kamuuzeni mawu ofewa
mwina Akalingalira (uthengawo)
kapena Akaopa".
45. (Iwo) adati: "Mbuye wathu
ndithu, Ife tikuopa kuti
angatimbwandire kapena
Kutipyolera malire (tisananene
Kanthu)".
W--**)*
«^sig£aj
^aftaJKa^i
ty%&&$&
] >W& r *
'#$$$%%
l/Jfi
1 Omasulira adati: Pamene adamtoia Musa akubanja la Farawo sadali
kuyamwa bele lamkazi aliyense, amakana, chifukwa Mulungu adamuletsa
kuyamwa mawere aakazi ena oyamwitsa. Ndipo mayi wake adali ndi
madandaulo ndi chisoni atamponya mumtsinje, ndipo adamulamula mlongo
wake kunka nafufuza zamwanayo. Pamene adafika kunyumba ya Farawo,
adamuona. Adati: "Kodi ndikulondolereni mkazi wokhulupirika, waulemu kuti
azikuyamwitsirani mwanayo?". Ndipo iwo adati pita kamtenge. Choncho
adadza ndi mayi wa Musa. Pamene adatulutsa bere lake, Musa adayamwa.
Choncho mkazi wa Farawo adasangalala kwabasi namuuza make Musa:
"Dzikhala pamodzi nane kunyumba yachifumu". lye adati: "Sindingathe kusiya
nyumba yanga ndi ana anga. Koma ndimtenga ndipo ndikhala ndikudza naye
nthawi iliyonse ukamufuna." Mkazi wa Farawo adavomereza ndi kumchitira
zaufulu mayiyo. Hi ndilo tanthauzo la mawu a Mulungu akuti, "Tidakubwezera
kwa mayi wako kuti diso lake litonthole, asadandaule".
Surat 20. Ta-Ha
Juzu 16
664
n *>i
y * <& 5jj-«»
46. (Mulungu) adati:
"Musaope.Ndithu Ine ndili nanu
pamodzi. Ndikumva, Ndiponso
ndikuona".
47. Choncho mpitireni,
ndikumuuza (kuti): "Ndithu, ife
ndife atumiki a Mbuye wako.
Asiye ana a Israeli achoke Ndi ife,
ndipo usawazunze; ndithu,
Takudzera ndi chozizwitsa
chochokera Kwa Mbuye wako
(chomwe ndi mboni Yathu
pazomwe tikukuuzazi), ndipo
Mtendere ukhala pa yemwe aatsate
Chiwongoko
48. Ndithu, zavumbulitsidwa
kwa ife kuti Chilango chiwapeza
amene akutsutsa (Zimenezi)
ndikuzitembenukira Kumbali."
49. (Farawo) adati: "Kodi
Mbuye wanu Ndani, iwe Musa?".
50. (Musa) adati: "Mbuye
wathu ndi yemwe Adapatsa
chinthu chilichonse Chilengedwe
chake, kenako Adachiongolera
(kutsata chimene Chikulingana ndi
chilengedwe chake)."
51. (Farawo) adati: "Nanga
mibadwo yakale Hi bwanji, (imene
idapita iwe Usadadze?)".
52. (Musa) adati: "Kudziwa
kwa zimenezo Nkwa Mbuye
wanga, m'kaundula (Wake
%% piQS^a^GN;
©ja^ap*
t^tfx&y&az
Surat 20. Ta-Ha
Juzu 16
665
n *>i
Y • & ^jj**'
Momwe mwasonkhanitsidwa
Chilichonse), Mbuye wanga
sasokera, Ndipo saiwala.
53. Yemwe adakupangirani
nthaka monga Choyala, ndipo
m'menemo adakuikirani Njira
ndikutsitsa madzi kuchokera
Kumwamba". Ndipo kupyolera
m'madziwo Tidameretsa mmera
Wosiyanasiyana.
54. Idyani ndikudyetsa ziweto
zanu. Ndithu, m'zimenezo muli
zisonyezo Kwa eni nzeru.
55. Kuchokera (m'nthaka) umu
tidakulengani, Ndipo momwemo
tidzakubwezani, ndipo Kuchokera
m'menemo tidzakutulutsani
Nthawi ina (muli moyo).
56. Ndipo, ndithu, tidamuonetsa
(Farawo) Zozizwitsa zathu zonse,
koma adatsutsa Ndipo adakana.
57. Adati: "Kodi watidzera kuti
utitulutse M'dziko lathu, ndi
matsenga ako,e, iwe Musa!
58. Choncho nafe
tikubweretsera matsenga Onga
amenewo! Choncho ika lonjezo
(La msonkhano) pakati pathu ndi
iwe; Lonjezo lomwe tisaliswe ife
ndi iwe, (Tidzakumane) pamalo
poyenera."
59. (Musa) adati: "Lonjezo lanu
likhale Pa tsiku lodzikongoletsa
Surat 20. Ta-Ha
Juzu 16
666
11 *>■»
Y » & °j> - '
(tsiku la Chikondwerero), ndipo
anthu Adzasonkhanitsidwe
m'mawa".
60. Ndipo Farawo adabwerera
ndikusonkhanitsa Matsenga ake,
ndipo kenako adabwera (Ndi
amatsenga ake pa tsiku la
chipanganolo).
61. Musa adawauza: "Tsoka
kwa inu! Musampekere bodza
Mulungu, kuopera kuti
Angakuphwasuleni ndi chilango.
Ndipo, Ndithu wataika amene
akupeka bodza."
62. Choncho (amatsengawo)
adakangana pakati Pawo pazinthu
zawo ndipo adakambirana
Mwachinsinsi.
63. (Iwo) adati
(mkunong'onezana Kwawo):
"Ndithu, anthu awiriwa Ndi
amatsenga; kupyolera mmatsenga
awo Akufuna kukutulutsani
m'dziko Mwanu, ndikuchotsa
chikhalidwe Chanu chomwe chili
chabwino.
64. Choncho sonkhanitsani
matsenga anu (Onse), kenako
mudze (kwa iwo) Mutandanda
pamzere; ndithu lero, Apambana
amene akhale wapamwamba."
* A» *
®(pj.^
%&\&s&$ym&
1 Ibun Abbas adati: Amatsenga adali okwana 72. Ndipo wamatsenga aliyense
adagwirizira m'manja mwake chingwe ndi ndodo. Izi zidalembedwa m'buku la
Tabarivi. Volumel 1 . tsamba 214.
Surat 20. Ta-Ha
Juzu 16
667
U ij*r\
T « *J? Sjj-*'
65. (Iwo) adati: "E, iwe Musa!
Kodi ukhala Ndiwe woyamba
kuponya (Matsenga ako), kapena
tikhala oyamba Ndife kuponya?"
66. (Musa) adati: "Koma inu
Ndinu muponye!" (Choncho
adaponya Matsengawo).
Mwadzidzidzi zingwe Zawo ndi
ndodo zawo zamatsenga awo,
Zimaoneka pamaso pake (Musa)
kuti Zikuyenda mothamanga.
67. Ndipo Musa adadzazidwa
ndi mantha Mumtima mwake.
68. Tidati: "Usaope, (zomwe
ukuzionazi); Ndithu, iwe ukhala
wopambana.
69. Ndipo ponya chimene chili
kudzanja Lako ladzanjadzanja
(ndodo); chimeza zomwe Apanga;
ndithu, iwo apanga matsenga a
mfiti Ndipo mfiti siingapambane
Paliponse pamene yadza". 1
70. Choncho amatsenga adagwa
Molambira uku akuti:
"Tamkhulupirira Mbuye wa
Haaruna ndi Musa."
»r\i'^i\\Z\*':' l'"«\\'-X'.
Ibun Kathiri adati: Pamene Musa adaponya ndodo idasanduka chinjoka
chachikulu chokhala ndi miyendo ndi khosi ndi mutu ndi mano. Chidayamba
kutsatira zingwezo ndi ndodozo mpaka chidameza zonsezo uku anthu akuona
masomphenya masana. Amatsenga ataona zimenezo, adazindikira
mwachitsimikizo kuti kusanduka kwa ndodoyo kukhala chinjoka sikudali
kwaufiti kapena matsenga. Koma chidali choonadi chopanda chipeneko.
Ndipo pamenepo onse adagwa ndi kulambira Mulungu. Tero chizizwa cha
Mulungu chidatsimikizika. Koma zopanda pake zidapita pachabe.
Surat 20. Ta-Ha
Juzu 16
668
n *>■»
Y% &
3j^
71. (Farawo) adanena: "Ha!
Mwamkhulupirira
ndisadakupatseni Chilolezo?
Ndithu, iye ndi mkulu Wanu
amene adakuphunzitsani
matsenga! Choncho ndikudulani
manja anu ndi Miyendo yanu,
mosemphanitsa: (Dzanja
lakudzanjadzanja ndi mwendo
Wakumanzere. Pomwe wina,
mkono Wakumanzere ndi mwendo
Wakudzanjadzanja), ndipo kenako
Ndikupachikani pamathunthu
Amitengo ya kanjeza; ndithu,
Mudziwa (panthawiyo) kuti ndani
Mwa ife, (ine kapena Mulungu wa
Musa),wachilango chaukali ndi
Chopitirira." 1
72. (Amatsenga) adati:
"Sitisankha iwe kusiya Zomwe
zatidzera; zisonyezo Zachoonadi
zoonekera poyera! Ndipo
tikumlumbirira Yemwe adatilenga,
(Sitikusankha iwe), chita zomwe
Ufuna kuchita; ndithu, iwe utha
Kupititsa chiweruzo chokhudzana
Ndi moyo uno wapansi, basi.
73. Ndithu, takhulupirira
Mbuye wathu Kuti atikhululukire
zolakwa zathu Ndimatsenga
amene watikakamiza (Kuchita);
ndipo Mulungu ndi Yemwe Ali
Imam Kurutubi adati: Ndithudi Farawo pa mawu akewa adalinga kuti
asokoneze anthu kuti asatsatire amatsengawo kuopera kuti angakhulupirire
monga iwo adakhulupirira.
Surat 20. Ta-Ha
Juzu 16
669
n tj*r\
y ♦ *y *j>^
Wabwino ndi Wamuyaya (osati
iwe)."
74. Ndithu, amene adzadze kwa
Mbuye Wake uku ali wamachimo,
adzapeza Moto wa Jahannama;
sadzafa M'menemo, ndipo
sadzakhalanso Ndi moyo wabwino.
75. Koma amene adzamdzera
uku ali Msilamu, Yemwe adachita
ntchito zabwino, iwo Ndi amene
adzapeze ulemerero
Wapamwamba,
76. Minda yamuyaya, yomwe
pansi pake ndi Patsogolo pake
pakuyenda mitsinje. Adzakhala
mmenemo muyaya. Ndipo
Zimenezo ndi mphoto za yemwe
Wadziyeretsa.
77. Ndipo ndithu, Musa
tidamtumizira Chivumbulutso,
(tidamzindikiritsa kuti): "Yenda
usiku ndi akapolo anga (kutuluka
M'dziko la Iguputo,) ndipo
ukawapangire Panyanja njira
youma, ndipo usaope Kukupeza
adani ndiponso usaope (kumira)."
78. Choncho Farawo pamodzi
ndi ankhondo ake, Adawatsata,
ndipo m'nyanjamo
Chidawaphimba chimene
chidawaphimba.
79. Ndipo Farawo
adawasokeretsa anthu ake, Ndipo
sadawaongolere.
^I'.iV.rt
%foj^j &j<afy>&$j
Surat 20. Ta-Ha
Juzu 16
670
n *>»
t • & ^jj-*'
80. E, inu ana a Israeli! Ndithu,
Tidakupulumutsani kwa mdani
wanu, ndipo Tidakulonjezani (kuti
mudze) mbali Yakudzanjadzanja
ya phiri (kuti Tikupatseni
malamulo ndi zina), ndipo
Tidakutsitsirani Manna ndi
Saluwa.
81. Idyani zinthu zabwino
zomwe Takupatsani, ndipo
musapyole malire Pazimenezo kuti
mkwiyo wanga Usakutsikireni;
ndipo amene mkwiyo Wanga
wamtsikira, ndiye kuti Ameneyo
waonongeka.
82. Ndipo ndithu, Ine ndi
Wokhululuka kwambiri Kwa
amene walapa ndi kukhulupirira
Ndikuchita ntchito zabwino,
kenako Ndikutsata chiongoko
mwaubwino.
83. "Nchiyani chakufulumizitsa
(kudza Kuno) kusiya anthu ako,
ee, iwe Musa?" 1
84. Adati: "Iwo ali pambuyo
panga akunditsata. Ndachita
changu kudza kwa Inu, Mbuye
wanga, kuti mundiyanje kwambiri".
85. (Mulungu) adati: "Ndithu,
Ife tawayesa Mayeso anthu ako
1 Imam Zamakhashariyi adati: "Musa
adazisankha zochokera mwa anthu ake,
yomwe idaikidwa. Kenako iye adatsogoi
chakhumbo ndi kufunitsitsa kumva mawu a
pamodzi ndi nthumwi zomwe
adamka kuphiri monga panyengo
a nasiya m'buyo anthu chifukwa
Mbuye wake".
Surat 20. Ta-Ha
Juzu 16
671
n *>«
T • *J? 3jj-*i
pambuyo pako; tero Samiriyu
wawasokeretsa". ]
86. Musa adabwerera kwa anthu
ake ali Wokwiya ndi wodandaula.
Adati :"E, inu anthu anga! Kodi
Mbuye Wanu sadakulonjezeni
lonjezo Labwino? Kapena nyengo
yalonjezolo Idatalika kwa inu?
Kapena mudafuna Kuti mkwiyo
ukutsikireni Kuchokera kwa Mbuye
wanu; Tero mwaswa lonjezo langa"?
87. (I wo) adati: "Sitidaswe
lonjezo lako Mwachifuniro chathu;
koma Tidasenzetsedwa mitolo ya
zodzikometsera Za anthu (ziwiya
zagolide zomwe Tidabwereka kwa
akazi a chimisiri), ndipo
Tidaziponya (pamoto, ndipo
Zidasungunuka ndikupangidwa
mwana Wang'ombe. )Ndipo
momwemonso Samiriyu Adaponya.
88. Ndipo adawatulutsira
(kuchokera M'golide
wosungunukayo) mwana
Wang'ombe wokhala ndi thupi
lokwanira, Yemwe adali kulira:
(iwo) adati: "Uyu ndi mulungu
wanu ndiponso mulungu wa Musa,
koma (Musa) Wamuiwala, (choncho
wapita kukamfuna Kuphiri)!"
89. Kodi sadaone kuti (mwana
wang'ombe) Sabweza mawu kwa
9&J2\J#%S%&
't'Jij 'i Hi ^ *>**'<
&$m^i&&%\
1 Samiriyu ameneyu adali wamatsenga, wachiphamaso (munafiku), wochokera
kumtundu wa anthu opembedza ng'ombe.
Siirat 20. Ta-Ha
Juzu 16
672
n *>»
Y • & 5jj*j
iwo, ndiponso Sangathe kudzetsa
matsautso kwa iwo Ngakhale
zothandiza
90. Ndipo Haaruna adawauza
kale (kuti)" "E, inu anthu anga!
Ndithu, inu Mwasokonezeka ndi
(chinthu) ichi. Ndithu, Mbuye
wanu ndi Mulungu Wachifundo
chambiri; choncho Nditsateni,
ndipo mverani lamulo langa,
(Siyani kupembedza fano ili)."
91. (Iwo) adati: "Sitisiya
ngakhale Pang'ono kumpembedza.
Kufikira Musa abwerere kwa ife,"
92. (Pamene Musa adabwerera)
adati: "E, I we Haaruna! Nchiyani
chidakuletsa Pamene udawaona
atasokera,
93. Kuti usanditsate?
Udanyozera Lamulo langa?"
94. (Haaruna) adati: E, iwe
mwana Wa mayi anga! Usagwire
ndevu Zanga,ngakhale mutu wanga
(Poukoka chifukwa cha mkwiyo).
Ndithu, ine ndidaopa (kuchoka ndi
Ena, kusiya ena) kuti ungati:
"Wawagawa ana a Israeli, ndipo
Sudayembekezere mawu anga".
95. (Musa) adati: "E, iwe
Samiriyu! Nchiyani wachita?"
96. (lye adati:) "Ndidaona
zomwe Sadazione ndipo ndidatapa
pang'ono Mapazi a Mtumiki
k"> ,f\ '<' " 9 <> ' *\i>\£
jl \»9 9 "{\\' 9>9''\\C
Surat 20. Ta-Ha
Juzu 16
673 n*>i
t • At
•-»-•
ndikuwaponya (M'mwana wa
ng'ombe). Ndipo Zimenezi ndi
zomwe zidakomera Mtima wanga" 1
97. (Musa) adati: " Choka,
ndithu Pa iwe (pali chilango)
pamoyo (wako) Choti uzingonena
(kuti) Musandikhudze
musandikhudze (Ndipo palibe
amene Adzakuyandikira ndipo iwe
Sudzayandikira aliyense). Ndithu,
Pa iwe pali lonjezo la (Mulungu)
Losaswedwa; ndipo muyang'ane
mulungu Wako, yemwe wakhala
Ukupitiriza kumpembedza.
Timtentha, kenako chipala
chakecho Tichiululutsa m'nyanja.
98. Ndithu, wompembedza
wanu, ndi Mulungu Yekha,
Yemwe, palibe woti
nkupembedzedwa Mwachoonadi
koma lye. Ndipo wakwanira
Pachilichonse kuchidziwa ndi
nzeru (Zake zopanda malire).
99. Umo ndi momwe
tikukusimbira nkhani Za (zinthu)
zomwe zidatsogola (za aneneri)
Ndithu takupatsa uthenga waukulu
kuchokera Kwa Ife (omwe ndi
Qur'an).
r^M^m^tk
Samiriyu adaona Gabrieli ali kudza kwa Musa atakwera hatchi. Choncho
adakondwera mumtima mwake kutapa mapazi ake. Tero ankati akaponya
zomwe adatapazo pachinthu chilichonse chakufa chinkauka. Ndipo pamene
fano la mwana wang'ombe lidakonzedwajye adatenga dothi la mapazi a
mthengayo nkuponya pafanolo. Choncho fanolo lidayamba kulira ngati
mwana wa ng'ombe.
Surat 20. Ta-Ha
Juzu 16
674
n *>»
t • & o
Ojf*
100. Amene aunyozere, ndithu,
iye tsiku La Kiyama adzasenza
Mitolo (ya machimo);
101. Adzakhala m'menemo
(m'chilango) muyaya. Ndipo ndi
zoipa zedi (kwa anthu) Kusenza
mitolo (imeneyo) tsiku la Kiyama,
102. (Kumbuka Mtumiki
Muhammad {SAW}), tsiku Lomwe
lipenga lidzaimbidwa. Ndipo
Tidzasonkhanitsa oipa tsiku
limenelo maso Awo ali a buluwu
(chifukwa cha mantha).
103. Adzanong'onezana pakati
pawo (ponena Kuti):
"Simudakhalitse padziko lapansi
Koma masiku khumi okha basi".
104. Ife tikudziwa kwambiri
zimene azidzanena Pamene
abwino awo pamayendedwe
Azidzanena: "Inu simudakhale
koma tsiku Limodzi basi
(poyerekeza ndi kuchuluka Kwa
masiku akumoto)".
105. Ndipo akukufunsa
zamapiri (kuti adzatani Tsiku la
Kiyama); auze: "Mbuye wanga
Adzawagumulagumula
ndikuwaululutsa (Ngati fumbi)
106. Ndipo adzaisiya (nthaka
yonse) ngati Bwalo losalazidwa
myaa!"
'9' 9[ 9'i<»\'.9>' <' 9 19&
&tSk403%&KZ
mg$x&$te^
Surat 20. Ta-Ha
Juzu 16
675
n *>»
y * ^y *jj~*
107. "Sudzaona kukhota
m'menemo ngakhale Chitunda
(chikweza)."
108. Tsiku limenelo
adzamtsatira woitana; Sadzatha
kumpatuka, ndipo mawu
(Azolengedwa) adzatonthola (Kuti
chete) kwa (Mulungu) Wachifundo
chambiri; Ndipo sudzamva, koma
kunong'ona Basi, ndi migugu ya
mapazi.
109. Tsiku limenelo chiombolo
(cha aliyense) Sichidzathandiza,
kupatula yemwe Wapatsidwa
chilolezo ndi (Mulungu)
Wachifundo chambiri, ndi
kumuyanja Kuti alankhule.
110. (Mulungu) akudziwa
Zapatsogolo pawo Ndizapambuyo
pawo. Ndipo iwo Sangathe
kumzindikira (Mulungu) Mmene
alili.
111. Ndipo nkhope (tsiku
limenelo) Zidzalobodoka pamaso
pa (Mulungu) Wamoyo
Wamuyaya, Wochita Chilichonse.
Ndithu, adzataika Kwathunthu
yense wochita zosalungama.
112. Ndipo amene achite
zabwino uku ali Msilamu,
sadzaopa kuchitiridwa zoipa
Kapena kumchepetsera
(Choyenera chake).
&$&$&&&$&
<&%&&&&%
^G^aWSWS
*Ql&&
Siirat 20. Ta-Ha
Juzu 16
676
n *>»
t * &
J>"
113. Ndipo momwemo
taivumbulutsa (Qur'an)
m'Chiarabu ndipo tafotokoza
M'menemo mwatsatanetsatane
Zamachenjezo (amtundu
uliwonse), Kuti aope (Mulungu),
ndikuti Nthawi iliyonse
(Qur'aniyo), iwapatse
Chikumbutso Chatsopano.
114. Watukuka Mulungu,
Mfumu ya choonadi, Ndipo
usaifulumizitse Qur'an
(Powerenga) chivumbulutso chake
Chisanamalizike kwa iwe, ndipo
nena (Popempha) kuti: "Mbuye
wanga! Ndionjezereni nzeru."
115. Ndipo tidamulangiza
(Mneneri) Adam Kale, koma
adaiwala. Ndipo sitidapeze Mwa
iye kulimba mtima (potsatira
Lamulo lathu loti asadye zipatso za
Mtengo woletsedwa).
116. Ndipo (kumbukirani)
pamene tidauza Angelo:
"Muchitireni sajida (mulambireni
Momulemekeza) Adam," ndipo
adachita Sajida kupatula Iblis,
Adakana.
117. Tsono tidati: "E, iwe
Adam! Ndithu, Uyu ndi mdani
wako iwe ndi mkazi wako;
Choncho asakutulutseni m'munda
Wamtendere, mungadzavutike.
Surat 20. Ta-Ha
Juzu 16
677 n*>»
Y * & ^jj- 1 '
118. Ndithu, iwe sumva njala
M'menemo ndipo sukhala
Wamaliseche,
119. Ndipo iwe sumva ludzu
m'menemo, Ndiponso sumva
kutentha".
120. Koma Satana
(adamsokoneza) Pomunong'oneza
(zoipa) adati: "E, Iwe Adam! Kodi
ndikusonyeze Mtengo wamuyaya
ndi (wopatsa) Ufumu wosatha?" 1
121. Ndipo (onse awiri)
adaudya, ndipo Umaliseche wawo
awiriwo Udaonekera poyera; ndipo
adayamba Kudziphatika masamba
am'mundamo; Ndipo Adamu
adalakwira Mbuye wake, choncho
adasokera.
122. Kenako Mbuye wake
Adamsankha pomulandira kulapa
Kwake ndikumuongola.
123. (Mulungu) adati:
"Chokani nonsenu M'menemo,
uku pali chidani pakati Pa wina ndi
mnzake, (padzakhala Chidani
pakati pa ana anu); koma
Chikadzakudzerani chiongoko
Kuchokera kwa Ine, ndipo amene
Adzachitsate chiongoko
Satana wotembereredwa adanena kwa iye m'njira yachinyengo kuti: "Kodi
iwe Adam, ndikusonyeze mtengo wakuti amene wadya zipatso zake,
adzakhala muyaya wosafa ndikupeza ufumu wonkerankera mtsogolo,
wosatha? Umo ndi momwe zidaliri ndate za satana. Sizidali zomufunira
zabwino Adam, koma kumuononga.
r? ] <^ \s*M&p3&^*^
©,
^fwV4\ -'x\<'*\.<\
>J*i$.
OJb
Surat 20. Ta-Ha
Juzu 16
678
>n *>»
Y ♦ de Ojj**
changacho, Sadzasokera ndiponso
sadzavutika.
124. Ndipo amene atanyozere
ulaliki wanga, Ndithu, moyo
wamavuto udzakhala pa lye ndipo
tidzamuukitsa m'manda tsiku La
chimaliziro ali wakhungu."
125. Adzanena: "Mbuye
wanga! Chifukwa ninji
mwandiukitsa ndili Wakhungu,
pomwe ndidali wopenya?"
126. (Mulungu) adzanena:
"Zimenezo Nchifukwa chakuti
zidakudzera Aya zathu koma
udaziiwala (Chifukwa
chosalabadira), momwemo Lero
uiwalidwa, (sulabadiridwa).
127. Ndipo umo ndimomwe
tidzamulipirire Aliyense wopyola
malire, Wosakhulupirira aya za
mbuye wake. Ndipo chilango cha
tsiku la Chimaliziro nchaukali,
ndiponso Chamuyaya.
128. Kodi sizidadziwikebe kwa
iwo kuti Ndi mibadwo ingati
tidaiononga Patsogolo pawo?
Ndipo awa (Osakhulupirira
atsopano) akuyenda M'malo awo,
(kodi saona zizindikiro
Zakuonongeka kwawo)? Ndithu,
NT zimenezo muli zisonyezo kwa
eni Nzeru.
129. Ndipo pakadapanda liwu
lomwe Lidatsogola kuchokera kwa
K^d&»&@$3#;
Siirat 20. Ta-Ha
Juzu 16
679
n *>i
Y * aJp ^jj- -
Mbuye wako (Lochedwetsera
chilango) ndi nthawi Yomwe
idaikidwa, ndithu (chilango)
Chikadawafika (tsopano lomwe
lino.)
130. Pirira pazomwe
akunenazo, ndipo Lemekeza
Mbuye Wako ndi kumtamanda,
Dzuwa lisanatuluke, ndiponso
Lisanalowe; ndiponso nthawi
zausiku Umulemekeze, ndi
pakatikati pa usana; Kuti udzapeze
zokukondweretsa (Tsiku la
Kiyama).
131. Ndipo usazitong'olere
maso ako (Mozidololokera zinthu)
zimene Tawasangalatsa nazo ena
mwa anthu Pakati pawo; zimenezo
nzokongoletsa Zamoyo wapadziko
basi, kuti tiwayese Mayeso
pazimenezo; koma chopatsa Cha
Mbuye wako (chomwe
Nchololedwa ngakhale chikhale
Chochepa) nchabwino kwambiri
Ndiponso chokhalitsa.
132. Ndipo lamula banja lako
kupemphera Swala ndi kuipirira
iwe mwini swalayo
Sitikukupempha riziki, (chakudya)
Koma Ife ndi amene tikukudyetsa
Ndipo malekezero abwino ali
Mukuopa (Mulungu).
133. Ndipo (osakhulupirira)
adanena: "Chifukwa ninji
sakutibweretsera Chizizwa
rwj*
&W&&$8&$\%
Surat 20. Ta-Ha
Juzu 16
680
n *>»
V • & o
ij^
kuchokera kwa Mbuye wake?"
Kodi sudawafike umboni
woonekera Wa zomwe zili
m'mabuku akale? (Kodi
sadakhutitsidwe ndi Qur'an
Chomwe ndi chizizwa
chachikulu)."
134, Ndipo ngati
tikadawaononga ndi Chilango,
asanadze uyo (Mtumiki),
Akadanena: "Mbuye wathu!
Bwanji Osatitumizira mtumiki kuti
titsate Aya zanu tisanayaluke ndi
Kunyozeka?"
135. Nena: "Aliyense (wa ife)
Akuyembekezera (mphoto yake);
Choncho yembekezerani.
Posachedwapa mudziwa kuti kodi
ndani Mwini njira yolingana,
ndipo ndani amene Waongoka."
«dS*«Ai^*
l \'*\i 9 ) 9 '\ 9 * ^99<9^ '<
Surat 21. Al-Anbiya' Juzu 17 I 681 I W^i t \ tLJ^i Sj^-.
SfjRAT AL-ANBIYA' XXI IjfiSs
KgQ^^B^y^^.. — _ _ _; r ^^i..>-^^^^,-Jr..y.jj
Surayi idavumbulutsidwa pambuyo pa Surati Ibrahim. Ndipo
ikufotokoza za kuyandikira kwa Kiyama kumene Amshirikina
ali kunyozera. Iwo akutinso mtumiki sangakhale munthu. Ndipo
nthawi zina amati Qur'an ndi ufiti; nthawi zina nkumati ndi
ndakatulo, nthawi zinanso amati ndi maloto osanganikira ndi
kunama, pomwe chenjezo lili chiimire patsogolo pawo. Ndipo
Aneneri adali anthu monga Muhammad (SAW).
Anthu akale adakana Aneneri awo monga momwe Akuraishi
adamkanira Muhammad(SAW). Koma Mulungu adaphwasula
midzi yawo. Ndithu, lye ngokhoza kuononga, ndiponso
ngokhoza kuisiya kuti inkerenkere mtsogolo. Ndipo chilichonse
chakumwamba ndi pansi ncha lye. Ndipo angelo m'makwerero
awo, amalemekeza Mulungu; safooka.
Ndithu, kulingana ndi kukhala bwino kwa thambo ndi nthaka,
ndichisonyezo chakuti amene adazipanga zimenezi ndi
m'modzi. Ndipo akadamthandiza aliyense, zikadaonongeka.
Ndipo aneneri onse adadza ndi ulaliki wopembedza Mulungu
m'modzi. lye alibe mwana. Ndipo aliyense wa iwo sanena kuti
iye ndi mnzake wa Mulungu. Ngati atatero ndiye kuti mphoto
yake ndi Jahena.
Mulungu Woyera wafotokoza zakukula kwa zolengedwa
Zake ndikudodometsa kwa kalengedwe ka thambo ndi nthaka.
Ndipo wafotokozanso chikhalidwe cha Amshirikina ndi
osakhulupirira. Kenaka wapitiriza kunenanso kuti Iye ndi amene
amasunga anthu. Ndipo walongosolanso za mphoto ya
osakhulupirira pa tsiku la chiweruzilo (Kiyama) ndipo
wakambanso nkhani ya Musa ndi Haaruna pamodzi ndi Farawo,
komanso ya Ibrahim pamodzi ndi anthu ake.Zakuti adamdalitsa
ndi ana abwino. Tsono Chauta wakambanso za Luti ndi anthu
ake ndi kuonongeka kwawo. Ndipo wakambanso za Nuhu ndi
kusakhulupirira kwa anthu ake; ndi kuwaononga onse psiti,
Surat 21. Al-Anbiya' Juzu 17
682
VV «.j*-i
T ^ *L-/!M 3jj-»
kupatula amene adakhulupirira. Wapitiriza Mulungu kukambanso
za Sulaiman, Daudi, Ayub, Ismaila, Idrisi, Zili Kifl, Zi Nnun ndi
Maryam.
Ndipo surayi yafotokozanso za nkhani ya Yaajuju ndi
Maajuju. kenako Mulungu wafotokoza za ntchito yabwino ndi
zipatso zake ndi zomwe adzawalipire omwe aopa ndikuchita
zabwino, ndi momwe adzakhalire pa tsiku la chimaliziro
(Kiyama). Ndipo wafotokozanso kuti Uthenga wa Muhammad
(SAW) ndi Mtendere kwa zolengedwa, ndikuti zinthu zonse
nzake Mulungu. Ndipo lye Ngoweruza bwino kuposa oweruza
ena onse.
Siirat 21. Al-Anbiya' Juzu 17 I 683 1 1 v *>i
Y> *Ui^5j>-
SuratAl-Anbiya'XXI
M'dzina la Mulungu waChifundo
Chambiri, waChisoni.
1. Chiwerengero chayandikira
kwa anthu Pomwe iwo ali
m'kusalabadirandi M'kunyozera.
2. Palibe pamene ukuwadzera
ulaliki Watsopano wochokera kwa
Mbuye wawo Koma
amaumvetsera uku akuchita
Zachibwana,
3. Mitima yawo ikunyozera
(osalabadira Zakudza kwa
Kiyama). Ndipo Akunenezana
mobisa amene adzichitira Zoipa;
(akuuzana motere:) "Kodi uyu
(Muhammadiyu) ndi ndani,
simunthu Monga inu? Kodi
mukuudzera ufiti Pomwe
mukuuona?"
4. (Mneneri
Muhammad {SAW}) adati:
"Mbuye wanga akudziwa zimene
Zikunenedwa kumwamba ndi
pansi; Ndipo lye Ngwakumva;
Ngodziwa.
5. Koma (osakhulupirira) adati:
"(Izi Zimene akufotokozazi) ndi
maloto Opanda pake." (Ndipo
nthawi zina Amati:)"Koma
zimenezi wazipeka." (Penanso
amati:) "Koma iyeyu Ndi
#,
o£*3\^3^J9-
£>
i*M$&\<X&&$$
Q *'V4P&
Surat 21. Al-Anbiya' Juzu 17 684 * V ^
t \ ;USl Oj>-
Mlakatuli. Chonchotu,
atibweretsere Chizizwa monga
mmene adatumiziridwa (Aneneri)
oyamba."
6. Sadakhulupirire apatsogolo
pawo, eni Midzi imene
tidaiononga (ngakhale Kuti
zozizwitsa adaziona); nanga Iwo
akhulupirira?
7. Ndipo sitidawatume
patsogolo pako, ( Iwe Mtumiki,)
koma anthu, (Osati Angelo);
tidawavumbulutsira
(Chivumbulutso Chathu.)
Choncho, Afunseni eni kudziwa
ngati Inu simukudziwa (nkhani
zakale).
8. Ndipo sitidawachite
(Aneneriwo) kukhala Matupi
osadya chakudya ndipo Sadalinso
amuyaya.
9. Kenako tidawatsimikizira
lonjezo (Lakuwathangata pa adani
awo), ndipo Tidawapulumutsa iwo
ndi amene Tidawafuna (mwa
omwe adawatsata), Ndipo olumpha
malire (a Mulungu)
Tidawaononga.
10. Ndithu, tatumiza kwa inu
Buku lomwe M'kati mwake muli
ulaliki wanu (Malangizo kwa inu).
Kodi simukuzindikira?
11. Ndi ambiri mwa eni midzi
yomwe idali Yosalungama,
X&\£$CJ6^}
9\?"\"
%&$$#%
wt%w$®$$\&
%$&&Z'0^\Z^&
Siirat 21. AI-Anbiya' Juzu 17 685 ^ V t>i
T > frLJ^I «j>->
tidawaononga; ndipo Pambuyo
pake tidalenga anthu ena.
12. Pamene adazindikira Za
chilango chathu, Pompo adayamba
kuchithawa.
13. Musathawe, ( kuthawa
Sikukupulumutsani), koma
bwererani Kuzimene
mwasangalatsidwa Nazo ndi
m'malo mwanu, kuti Mufunsidwe.
14. Adanena: "Tsoka lathu
ndithu, tidali Ochita zoipa".
15. Kukuwa kwawoko
sikudathe, kufikira Tidawapanga
ngati (mbewu) Zokololedwa,
mpaka kupuma kwawo Kudazima
(adafa).
16. Ndipo sitidalenge thambo
ndi nthaka Ndi zapakati pake,
mwamasewera.
17. Tikadafuna kupanga choti
tiziseweretsa (Sitidakapanga
zomwe mukuzionazi) Koma
tikadapanga mwazomwe tili nazo,
Tikadakhala ochita zachibwana.
18. Koma (chimene timachita
ndi ichi), Timachiponya choona pa
chachabe ndi Kuchiswa bongo
bwake, ndipo Chachabecho
chimachoka. Ndipo Chilango chili
pa inu chifukwa cha Zomwe
mukunena (Kumnamizira
Mulungu).
©U-
'M>>~J<rw.<.\
®<
'9 ^ \* !> '
Surat 21. AI-Anbiya' Juzu 17 686 > V *>i
t ^ frW^ 1 5 jj-»
19. Onse akumwamba ndi
pansi, Ngake (Mulungu); ndipo
amene ali kwa lye (Angelo),
sadzitukumula Pakumulambira,
ndiponso satopa (Ndi
mapemphero)
20. Amamlemekeza usiku ndi
usana,ndipo Sagwidwa ndi ulesi.
21. Kapena adzipangira
milungu yochokera M'nthaka
youkitsa akufa, (kotero kuti
Aichita kukhala milungu yawo
mmalo Mwa Mulungu)?
22. Kukadakhala kuti ilipo
M'menemo milungu ina
(kuthambo ndi Pansi) kupatula
Mulungu, (ziwirizi)
Zikadawonongeka, wapatukana
Mulungu Mbuye wa mpando
Wachifumu ndi zimene akunena
(Osakhulupirira).
23. Safunsidwa pazimene
akuchita, Koma iwo adzafunsidwa.
24. Kapena adzipangira
milungu ina M'malo mwa lye?
Nena: "Bweretsani Umboni wanu
(pazimenezi), (Izi ndikuuzani)
ndichikumbutso kwa Awa ali
pamodzi ndi ine, ndiponso
Ndichikumbutso kwa amene
adalipo Patsogolo panga." Koma
ambiri a iwo Sadziwa zachoonadi,
tero iwo Akunyozera.
Surat 21. Al-Anbiya' Juzu 17 I 687 h V *>i
X ^ *A~^M «jj-»
25. Ndipo sitidatume patsogolo
pako Mneneri aliyense koma tidali
Kumzindikiritsa kuti palibe
Mulungu Wina wompembedza
mwachoonadi, Koma Ine; choncho
ndilambireni.
26. Ndipo (osakhulupirira)
akuti: "(Mulungu) Wachifundo
chambiri wadzipangira Mwana."
Mulungu wapatukana (ndi
Zimenezo) koma (awa angelo) ndi
akapolo (A Mulungu) amene
alemekezedwa.
27. Samtsogolera kulankhula,
ndipo iwo Amachita molingana ndi
malamulo Ake.
28. (Mulungu) akudziwa
zapatsogolo pawo (Angelowo) ndi
zapambuyo pawo,ndipo
(Angelowo) sangaombole
(aliyense) Koma yekhayo
(Mulungu) wamuyanja, Ndipo
iwo, chifukwa chomuopa,
Amanjenjemera.
29. Ndipo mwa iwo amene
anganene kuti: "Ine ndi mulungu
mmalo mwa lye," Ndiye kuti
timulipira Jahannama; umo Ndi
momwe timawalipirira ochita
zoipa.
30. Kodi osakhulupirira
sadaone kuti Thambo ndi nthaka
Zidali zophatikizana, Ndipo
tidazilekanitsa? Ndipo ndi madzi
111 1 -*.*. 9 > 9 » ( 9\W#\ »* 9 \K& 9 "
Surat 21. Al-Anbiya' Juzu 17
688
W *>i
t 1 *LJ^ 5jJ~»
Tidalenga chilichonse chamoyo.
Kodi Sakhulupirira?
31. Ndipo tidaika mapiri
panthaka Molimbika kuti
isagwedezeke ndi iwo, Ndipo
m'menemo tidaikamo misewu
Kuti alondole njira (Ndikufika
komwe afuna).
32. Ndipo thambo tidalipanga
monga Tsindwi losungidwa (kuti
lisagwe): Koma iwo
akuzitembenukira kumbali
Zizindikiro zake.
33. Ndipo lye ndi Yemwe
adalenga usiku ndi Usana, dzuwa
ndi mwezi; chilichonse Mwa izo
chikusambira mozungulira M 'njira
mwake.
34. Ife sitidawachite anthu
amene adalipo Patsogolo pako
kukhala amuyaya. Nanga Ukafa,
kodi iwo adzakhala muyaya?
35. Chamoyo chilichonse
chidzalawa imfa; Ndipo
tikukuyesani mayeso ndi zinthu
Zoipa ndi zabwino. Ndipo nonsenu
Mudzabwezedwa kwalfe.
36. Ndipo amene
sadakhulupirire akakuona,
Akungokuchitira chipongwe.
"Kodi Ndi uyu yemwe akutchula
milungu yanu (Mwachipongwe)?"
Pomwe iwo ndi Amene akukana
***)
Surat 21. Al-Anbiya' Juzu 17 689 I ^ V *>i
Y > frLJ^I 5jj--
zakutchula (Mulungu) Wachifundo
Chambiri.
37. Munthu walengedwa ndi
chikhalidwe Chokonda zinthu
(zake zonse) Mwachangu.
Posachedwapa Ndikusonyezani
zisonyezo Zanga; choncho
musandifulumizitse
(Kukubweretserani chilango
changa)
38. Ndipo (osakhulupirira)
akuti: "Kodi Malonjezo awa
adzakwaniritsidwa liti, Ngati
mukunena zoona?".
39. Chikhala kuti amene
sadakhulupirire Akudziwa
chilango chimene Chidzawapeza
panthawi yomwe Sangathe
kutchinjiriza moto kunkhope Zawo
ndi kumisana yawo ndipo kuti
Sadzathandizidwa, (sakadanena
Zimenezi.)
40. Koma (Kiyama)
idzawadzera Mwadzidzidzi ndi
kuwadzidzimutsa; Ndipo kenako
sadzatha kuibweza Kapena
kupatsidwa danga (kuti achite
Zomwe sadachite.)
41. Ndipo ndithu, Atumiki
adachitidwa Chipongwe patsogolo
pako; choncho Amene adachita
chipongwe mwa iwo, Zidawadzera
zomwe adali kuzichita Chipongwe.
1 -•"'
©U&x*
f 9J*J'*'"Z t. '*' 9 9 *\* 9\'
9S
(3^<i^^L^^^^^
u
ysi>\c»>\ \»f.">
A *' 9 9 9*9*
Surat 21. Al-Anbiya' Juzu 17 I 690 I S V *>t
T > frW^ 1 *jj~»
42. Nena: "Kodi ndani
angakutetezeni usiku Ndi usana ku
masautso a (Mulungu)
Wachifundo Chambiri?" Koma
iwo Akunyozera kukumbuka
Mbuye wawo.
43. Kapena ali nayo milungu
yowatchinjiriza M'malo mwa Ife?
(Milunguyo) siingathe
Kudzithandiza yokha (nanga ndiye
Ingathe kuthandiza ena?) Ndipo
(Milungu) imeneyo
siidzasamalidwa Ndi Ife.
44. Koma awa (osakhulupirira)
Tidawasangalatsa ndi Makolo awo
kufikira Nthawi ya moyo wawo
idatalika; kodi Saona kuti
tikulidzera dziko lawo
Ndikulichepetsa malire ake?.
Nanga kodi iwo ndiwo opambana?
45. Nena: "Ndithu,
ndikukuchenjezani ndi
Chivumbulutso (cha Mulungu).
"Koma Agonthi samva kuitana
pamene Akuchenjezedwa".
46. Ndipo kukadawakhudza
kumenya kumodzi Kwa chilango
cha Mbuye wako, Ndithudi,
(akadadzichepetsa nthawi
Yomweyo). Akadanena: "Tsoka
kwa Ife ndithu,tidali osalungama".
47. Ndipo tsiku la Kiyama
tidzaika masikero Achilungamo,
choncho mzimu uliwonse
9 <*' V. 9' *S 9i' h \'<>\\
\S99 ** ?* K 9'9$g'*i 9,<*<
-^\^\&&\>&
Surat 21. Al-Anbiya' Juzu 17 I 691 ) V ^jJfc-i
t > *lj^ 5^
Sudzachitidwa chinyengo pa
Chilichonse.Ngakhale
(chinthucho) Chili cholemera ngati
njere ya mpiru, Tidzachibweretsa;
ndipo tikukwana (Kukhala
akatswiri) pa chiwerengero.
48. Ndipo ndithu, Musa ndi
Haaruna Tidawapatsa (buku)
losiyanitsa pakati Pachoonadi ndi
chonama, ndiponso muuni Ndi
ulaliki kwa anthu Oopa Mulungu
49. Omwe akumuopa Mbuye
wawo Ngakhale ali paokha,
omwenso Amaopa Kiyama.
50. Ndipo iyi (Qur'an) ndi
ulaliki Wodalitsidwa umene
tauvumbulutsa (kwa Inu); kodi inu
mukuikana?
51. Ndipo ndithu, Ibrahim
tidampatsa Kulungama kuyambira
kale (kuubwana), Ndipo
tinkamudziwa (bwinobwino).
52. (Akumbutse anthu) pamene
adauza A bambo ake ndi anthu
ake, "Nchiyani mafano awa omwe
inu Nthawi zonse mukupitiriza
Kuwapembedza."
53. Adati: "Tidapeza makolo
athu Akuwapembedza.(Choncho
nafenso Tikuwapembedza)".
54. (lye) adati: "Ndithu, inu ndi
makolo Anu mudali mkusokera
koonekera."
*** "x^ V-**^ £&**'** <i#^
9 l'\}"9 \»fo9S\3'<"
Surat 21. AI-Anbiya' Juzu 17 692 ^ V *>i
r ^ tu^i oj^-.
55. (Iwo) adati: "Kodi
watibweretsera Choonadi, kapena
iwe ndi m'modzi Mwa osereula?"
56. (lye) adati: ("Iyayi, ine
siwosereula), Koma Mbuye wanu,
ndi Mbuye Wathambo ndi nthaka
amene adalenga Zimenezi; ine
pazimenezi, ndine M'modzi
wochitira umboni".
57. "Ndipo ndikulumbirira
Chauta, Ndiwachitira chiwembu
mafano Anuwo pambuyo
ponditembenukira Misana kupita
komwe mukupita."
58. Choncho adawaphwanya
(mafanowo), Zidutswazidutswa
kupatula lalikulu lawo (Sadaliswe)
kuti iwo alibwerere (ndi Kulifunsa
zimene zachitika).
59. (Iwo pamene adafika
kumafano awo) Adati: "Ndani
wachita ichi pa Milungu yathu?
Ndithu, iye ndi M'modzi waochita
zoipa."
60. Adati: "Tidamumva
m'nyamata wina Akuitchula
(moipa); amatchedwa Ibrahim."
61. Adati: "Mubweretseni
pamaso Pa anthu kuti amuone."
62. Adati: "Kodi ndiwedi
Wachita ichi ku milungu yathu,
Ee, iwe Ibrahim?"
\' 9
<36%$Z\lZ\ooS&$6j
®(j&j£$j$
Surat 21. Al-Anbiya' Juzu 17
693
W*>l
t > *Ljty 5j>-»
63. (lye) adati: "(Iyayi), koma
wachita Ichi ndi mkulu wawoyu.
Choncho Afunseni (kuti akuuzeni
zenizeni) Ngati amatha
kuyankhula."
64. Ndipo adadzitembenukira
okha Ndikunena kuti: "Ndithu, inu
ndinu Oipa."
65. Kenako adazyolitsa mitu
yawo (Ndikubwerera kuumbuli
wawo) Nanena kuti, "Ndithu, iwe
ukudziwa Kuti izi siziyankhula
(nchifukwa ninji Ukutichita
chipongwe)?"
66. (lye) adati: "Kodi
mukupembedza Zomwe
sizingakuthandizeni chilichonse,
Kusiya Mulungu, zomwenso
Sizingakupatseni masautso?"
67. "Kuyaluka nkwanu ndi
zomwe Mukuzipembedzazo kusiya
Mulungu. Kodi simuganizira?"
68. (Iwo) adati: "Mtentheni;
ndipo pulumutsani Milungu yanu,
ngati inu mungathe Kuchita
zimenezi."
69. Tidati: "E, iwe Moto! Khala
kuzizira Ndiponso mtendere kwa
Ibrahim".
70. Ndipo adamfunira
chiwembu; koma Tidawachita
kukhala otaika zedi.
©
Surat 21. Al-Anbiya' Juzu 17
694
W *>i
t > f-W^' *j>-»
71. Ndipo tidampulumutsa iye
ndi Luti kupita kudziko lomwe
tidalidalitsa Ku zolengedwa.
72. Ndipo (Ibrahim) tidampatsa
Isihaka ndi Kuonjezera Yakubu,
ndipo tidawachita Onse kukhala
abwino.
73. Ndipo tidawasankha
Kukhala atsogoleri, Owongolera
mwalamulo lathu, ndipo
Tidawazindikiritsa kuchita
zabwino ndi Kupemphera swala,
ndi kupereka Zakat; ndipo adali
odzichepetsa kwa Ife.
74. Ndipo Luti tidampatsa
luntha ndi Kuzindikira, ndipo
tidampulumutsa Kumudzi womwe
Anthu ake ankachita Zoipa; ndithu
iwo adali anthu oipa Otuluka
m'chilamulo (cha Mulungu).
75. Ndipo tidamulowetsa
kuchifundo chathu; Ndithu, iye
adali m'modzi waochita Zabwino.
76. Ndipo (akumbutse za) Nuhi,
pamene Adatiitana kale
(kutipempha). Ndipo Ife
tidamuyankha ndi kupulumutsa iye
Ndi anthu ake kusautso lalikulu.
77. Ndipo tidampulumutsa pa
anthu amene Adatsutsa aya zathu;
ndithu, iwo adali Anthu oipa.
Ndipo onse tidawamiza (Ndi
chigumula chamadzi).
©
(^QZ$S'j%&
Surat 21. Al-Anbiya' Juzu 17
695
W fr>»
t ^ s-W*^ ^JJ—
78. Ndipo (akumbutse za)
Daudi ndi Sulaiman, Pamene
ankaweruza mlandu wa munda
Pomwe mbuzi za anthu zidadya
ndi Kuonongaononga usiku
mmenemo ndipo Ife tidali mboni
pa kuweruza kwawo.
79. Tidamzindikiritsa za
mlanduwo Sulaiman (kuposa tate
wake Daudi). Yense waiwo
tidampatsa kuweruza Mwaluntha
ndi kudziwa; ndipo Tidagonjetsa
mapiri ndi mbalame kuti Zikhale
pamodzi ndi Daudi Zikulemekeza
Mulungu; ndithu, Ife ndi ochita
chimene tafuna.
80. Ndipo tidamphunzitsa
(Daudi) kapangidwe Kachovala
chapankhondo chifukwa Cha inu
kuti chikutetezeni mkumenyana
Kwanu; kodi simungakhale
othokoza?
81. Nayenso Sulaiman
tidamufewetsera mphepo
Yamphamvu; inkayenda
mwalamulo lake Kunka kudziko
lomwe talidalitsa (Dziko la
Shamu); ndipo Ife pa Chilichonse
Ngodziwa.
82. Ndipo (tidamufewetseranso)
Asatana Omwe ankamubirira
m'madzi (Ndikumtolera ngale),
ndipo ankachita Ntchito zina
kuonjezera pa zimenezi; Ndipo Ife
tidali owalondera.
Surat 21. Al-Anbiya' Juzu 17 696 > V *>)
t > *W»SM 3j>*-
83. Ndipo akumbutsenso za
Ayubu pamene Adakuwira Mbuye
wake (kuti); "Ndithu mavuto
andikhudza, pomwe Inu Ndi
Achifundo kuposa achifundo!"
84. Choncho tidavomera
(pempho lake); ndipo
Tidamchotsera mavuto omwe adali
Nawo, ndipo tidampatsa ana ake
Ofanana ndi omwe adali nawo kale
Ndikuonjezeranso ena onga iwo,
(Zonsezi monga) chifundo
chochokera Kwa Ife, (ndikuti
zikhale) chikumbutso Kwa ochita
mapemphero.
85. Ndipo (mutchule) Isimaila
ndi Idrisa Ndi Zul Kifli, onsewa
adali Mwa opirira;
86. Tidawalowetsanso
kuchifundo chathu, Ndithu, iwo
adali mwa Anthu abwino.
87. Ndipo (mutchulenso) Zun-
nun (Yunusu), Pamene adachoka
uku atakwiya, ndipo Ankaganiza
(kuti tamuloleza kusamuka)
Ndikuti sititha kumchita kanthu.
Choncho Adaitana mumdima
(wam'mimba Mwansomba imene
idamumeza, kuti): "Ndithu, palibe
mulungu wina Wopembezedwa
mwachoonadi koma Inu;
mwayeretsedwa; ndithu, ine
ndidali M'modzi wa odzichitira
zoipa."
©
©<i^oJ!^
Surat 21. Al-Anbiya' Juzu 17 597 > V *>i
Y ^ *LJ^ ojj^
88. Choncho tidavomereza
(pempho lake) ndi Kumpulumutsa
ku madandaulo; umo ndi M'mene
timapulumutsira okhulupirira.
89. Ndipo (akumbutse za)
Zakariya pamene Adaitana Mbuye
wake (kuti): "Mbuye Wanga!
Musandisiye ndekha; Ndithu, Inu
ndinu wabwino kuposa alowa
mmalo Onse."
90. Choncho tidamuvomera
(pempho), Ndikumpatsa Yahaya
ndikumkonzera Mkazi wake.
Ndithu iwo adali achangu Pochita
zabwino; ankatipempha
Mwakhumbo ndi mwamantha,
Ndipo adali Odzichepetsa kwa Ife.
91. Ndipo (atchulire za mkazi)
yemwe Adauteteza umaliseche
wake (pozisunga); Ndipo tidauzira
mwa iye Mzimu Wathu, Ndipo
tidamchita iye ndi mwana Wake
kukhala chizizwa (cha Mulungu)
Kwa zolengedwa zonse.
92. Ndithu, uwu mpingo wanu,
ndimpingo Umodzi, ndipo Ine
ndine Mbuye wanu; Choncho
ndipembedzeni.
93. Koma iwo adaswa chinthu
chawochi Pakati pawo (tero
adakhala mipingo
Yosiyanasiyana). Onse
adzabwerera kwa Ife.
9*< "Xti ^ 9< 9* ? < '
© (ift-^^ 1
%3p
Surat 21. AI-Anbiya' Juzu 17
698
W*jJt-i
T 1 frLJ^l ojj~-
94. Ndipo amene achite ntchito
zabwino Uku ali Msilamu, khama
lake Silidzakanidwa; ndithunso, Ife
Tikumlembera zonse zimene
akuchita.
95. Ndipo nkosatheka kwa eni
mudzi umene Tidauononga
chifukwa cha machimo Awo kuti
asabwerere kwa Ife; (Koma ndithu
abwerera).
96. Kufikira pamene (mpanda
wa) Yaajuju Ndi Maajuju
adzatsekulidwa, ndipo Iwo
adzakhala akuthamanga kuchokera
M'phiri lililonse.
97. Ndipo lonjezo lachoonadi
Lidzafika; pamenepo maso a
omwe Sadakhulupirire,
adzatong'oka Uku akunena:
"Tsoka pa ife. Ndithu, tidali
osalabadira (zachinthu) Ichi; koma
tidali oipa, (odzichitira tokha
Zoipa.")
98. Ndithu, inu ndi amene
Mukuwapembedza kusiya
Mulungu, Ndinu nkhuni za ku
Jahannama. Ndipo inu
(Jahannamayo) mudzaifika.
99. Ngati awa akadakhala
milungu Yeniyeni, ndiye kuti
sakadaifika (Sakadailowa)
mmenemo onse adzakhala
muyaya.
<zs'A >.& " Vs 9*
Surat 21. Al-Anbiya' Juzu 17
699
W*j*-»
t > ^ljVi Ojf
100. Mmenemo iwo adzakhala
akubuula Ndipo iwo mmenemo
sadzamva (Chifukwa makutu
adzagontha).
101. Ndithu, amene ubwino
wathu Udawafika, iwo
adzatalikitsidwa nawo (Motowo).
102. Sadzamva mavume ake,
ndipo iwo Adzakhala muyaya
m'zomwe Ikukhumba mitima
yawo.
103. Kugwedezeka kwakukulu
Sikudzawadandaulitsa; Ndipo
angelo adzawalandira
(Ndikuwauza): "Hi ndi tsiku lanu
Lomwe mudali kulonjezedwa."
104. Tsiku lomwe tidzakulunga
thambo Monga momwe
amakulungira makalata Okhala ndi
malembo m'kati mwake; Monga
tidayamba kulenga Zolengedwa
poyamba, Tidzabwerezanso
(kuzilenga kachiwiri. Ndipo
aliyense adzalipidwa pazomwe
Adali kuchita) ili ndilonjezo
lomwe Lili pa Ife. Ndithu, Ife ndi
Ochita (zomwe tikunena.)
105. Ndipo ndithu, tidalemba
m'zaburi (M'masalimo buku la
Daudi) pambuyo Polemba mu
Lauhil-Mahafudh Kuti:"Dziko
(lapansi) adzalilowa Akapolo
Anga abwino."
^ 'iXp^ ^h^' (!£&*$
Siirat 21. Al-Anbiya' Juzu 17
700
W frjJfe-i
Y 1 *W^H 5 j>-
106. Ndithu, pazimenezi
(nkhani za aneneri), Pali miyambo
kwa anthu, opembedza (Mulungu).
107. Ndipo sitidakutume koma
kuti ukhale Mtendere kwa
zolengedwa zonse.
108. Nena: "Ndithu,
kukuvumbulutsidwa Kwa ine kuti
Mulungu wanu ndi Mulungu
mmodzi; nanga inu Mudzagonjera
(zofuna Zake Polowa
m'Chisilamu)?"
109. Koma ngati anyozera,
nena: "Ndalengeza Uthenga kwa
inu Mofanana (popanda tsankho);
Sindidziwa kuti zomwe
Mukulonjezedwa zili pafupi
Kapena zili kutali.
110. "Ndithu, lye akudziwa
mawu Okweza, ndiponso
akudziwa zomwe Mukubisa.
111. "Ndipo sindikudziwa,
mwina Kuchedwetsa chilango
chanu ndi mayeso Akukuyesani
ndikukusangalatsani Ndi zokoma
(za M'dziko) mpaka Idzakwane
nthawi yoikidwayo."
112. Adati: "E, Mbuye wanga.
Weruzani moona." "Ndipo Mbuye
Wathu ndi (Mulungu) Wachifundo
Chambiri; wopemphedwa
chithandizo Pazimene
mukusimbazo."
®<i#^^>$ ^mI^Uu!
*&£j3fc2hM3fcj
Surat 22. Al-Hajj Juzu 17 701 W *jJH
tt
r^t a^j-***
SURAT AL-HAJJ XXII
t==^
Surayi yayamba ndi nkhani yoopseza kwambiri, yomwe
inganjenjemeretse mitima ndi kuchotsa nzeru chifukwa
chakuopsa kwake. Ndipo kumeneko ndiko kugwedezeka kwa
dziko mwamphamvu komwe kudzachitika patsogolo patsiku la
Kiyama.
Kugwedezeka sikudzakhala kwa mapiri ndi nyumba basi,
koma kudzakhalanso amayi oyamwitsa ndi amayi apakati kotero
kuti oyamwitsa sadzalabadira za ana awo; naonso apakati
adzataya pakati pawo nthawi isadakwane. Ndipo anthu
adzakhala ali dzandidzandi ngati aledzera ndi mowa. Sikuti
aledzera ndi mowa, koma kugwedezeka koopsa kwadziko
komwe nkonjenjemeretsa mitima kwambiri.
Surayi ikufotokozanso za zizindikiro zosonyeza kuuka ku
imfa ndi kunka kunyumba yolandirira mphoto kuti munthu
akalandire mphoto yake; mphoto ya chabwino, njabwino,
mphoto ya choipa, njoipa.
Surayi ikulongosolanso za maonekedwe a tsiku la Kiyama:
abwino adzakhala ku nyumba ya mtendere ndipo oipa adzakhala
kunyumba yachilango cha moto.
Surat 22. Al-Hajj Juzu 17
702
\V *jk-\
YY
g^ l5 J>*
Surat Al-Hajj XXII
y
M'dzina la Mulungu waChifundo
Chambiri, waChisoni.
1. E, inu anthu! Opani Mbuye
wanu (ndipo Kumbukirani tsiku la
Kiyama). Ndithu, Kugwedezeka
kwa Kiyama ndichinthu
Chachikulu (kwabasi).
2. Tsiku limene mudzaione
(Kiyamayo), Mkazi aliyense
woyamwitsa adzaiwala (Mwana
wake) womuyamwitsa, ndipo
(Mkazi) aliyense wapakati
adzataya Pakati pake; ndipo
udzawaona anthu Ataledzera,
pomwe sadaledzere; koma Ndi
chilango chaukali cha Mulungu
(Chimene chawapeza).
3. Ndipo alipo ena mwa Anthu
amene akutsutsa Za Mulungu
popanda Kuzindikira, ndipo
akutsatira Satana aliyense
wolakwa.
4. (Za Satana), kwalembedwa
kuti amene Amsankhe kukhala
bwenzi lake, ndithujye
amsokeretsa ndi kumtsogolera
Kuchilango cha moto.
5. E, inu anthu ngati muli
m'chikaiko zakuuka ku Imfa,
(ndipo mukuona kuti nzosatheka,
Yang'anani mmene
feVi
■ -
Q^I^I^W-
-£>
Surat 22. Al-Hajj Juzu 17 703 > V *>»
XY
g^ 5 ^
tidakulengerani). Ndithujfe
tidakulengani ndi dothi, ndipo
(Timakulengani) ndi dontho la
umuna, komanso (Umunawo
udasanduka) gawo lamagazi,
Kenako gawo la mnofii
woumbidwa (chithunzi
Chamunthu) ndi wosaumbidwa,
kuti Tikulongosolereni (kukhoza
kwathu;) ndipo Ife
Timachikhazikitsa mchiberekero;
chimene Tifuna kufikira nthawi
yake yoyikidwa kenako
Timakutulutsani muli khanda,
(tsono Timakulerani) kuti mufike
pamsinkhu wanu. Ndipo ena mwa
inu amamwalira (asanakule)
Pomwe ena mwa inu
amabwezedwa kumoyo Wofooka
(waukalamba) kotero kuti
asadziwe Chilichonse pambuyo
pakuti adali wodziwa. Ndipo
umaiona nthaka ili chetee, koma
Tikatsitsa madzi pamwamba pake,
imagwedezeka Ndi kufufuma, ndi
kumeretsa mtundu Uliwonse wa
mmera wokongola. 1
6. Zimenezo (monga kulenga
munthu ndi kumeretsa Mmera, ndi
umboni wosonyeza) kuti Mulungu
Woona alipo; ndikuti iye
1 Munthu amene ali ndi chikaiko zakuuka kuimfa, pafunika kuti aganizire
zomwe zili m'ndime iyi yolemekezeka kuti aone komwe wachokera ndi komwe
wafika. Kenako aone nthaka polingalira mozama momwe imakhalira yachilala.
Koma mvula ikaivumbwira ndikudzuka, kuti adziwe kuti amene akuchita
zimenezi palibe chomwe angalephere.
Surat 22. Al-Hajj Juzu 17
704
1V*j*-l
tt
S^ 5 J>*
amaukitsa akufa, Ndiponso lye ali
ndi mphamvu pachilichonse.
7. Ndipo, ndithu, Kiyama
idza;palibe Chikaiko pazimenezi,
ndipo ndithu, Mulungu
adzawatulutsa amene ali m'manda.
8. Ndipo alipo mwa anthu
amene akutsutsa za Mulungu
popanda kuzindikira, Ngakhale
chiongoko, ndi Buku lounika,
(Koma makani basi ndi kungotsata
zimene Akuziganizira). 1
9. (Yemwe) akupinda khosi
lake (chifukwa Chodzikuza) kuti
asokeze (anthu powachotsa)
Kunjira ya Mulungu; pa iye pali
chilango Choyalutsa pamoyo uno,
ndipo patsiku la Kiyama
tikamulawitsa chilango chamoto
Wotentha.
10. (Tidzamuuza kuti): "Izi ndi
zomwe Manja ako adatsogoza;
ndithu, Mulungu siwachinyengo
kwa akapolo (Ake)."
11. Ndipo alipo wina mwa
anthu amene Akupembedza
Mulungu cham'mphepete
(Mwachipembedzo). Chabwino
1 Kutsutsana pa zinthu za chipembedzo popanda kudziwa ndi kukhala ndi
umboni wokwanira.nkoletsedwa zedi.
Maphunziro enieni amene angamzindikiritse munthu za chipembedzo, ndi
omwe akupezeka m'Qur'an ndi m'mahadisi a Mtumiki (Mtendere ndi madalitso
a Mulungu akhale pa iye) omwe ali oona, ndi maphunziro amene akupezeka
m'mabuku ophunzitsa malamulo achipembedzo omwe ali ovomerezeka ndi
atsogoleri a Chisilamu, osati buku lililonse lolembedwa ndi munthu wamba.
Surat 22. Al-Hajj Juzu 17
705
W*>»
tt
e^*j>*
chikampeza Amatonthola nacho;
koma masautso akamufika,
Amatembenuka ndi nkhope yake
(posiya Chikhulupiriro mwa
Mulungu. Choncho) Waluza moyo
wadziko lapansi ndi moyo wa tsiku
La chimaliziro; kumeneko ndiko
kuluza Koonekera. 1
12. M'malo mwa Mulungu,
amapembedza zomwe
Sizingampatse masautso (ngati
ataleka Kuzipembedza), ndiponso
zomwe Sizingampatse chithandizo
(akamazipembedza) Ndipo
kumeneko ndiko kusokera
kwakukulu.
13. Akupembedza omwe
masautso awo ali Pafupi zedi
poyerekeza ndi zabwino zawo,
Taonani kuipa atetezi ndiponso ndi
abwenzi oipa.
14. Ndithu, Mulungu
adzalowetsa kuminda Yamtendere
amene akhulupirira Ndikuchita
zabwino, mitsinje ikuyenda Pansi
(pa mindayo). Ndithu, Mulungu
Amachita chimene wafuna.
15. Amene akuganiza kuti
Mulungu Samthangata (Mtumiki
wake) padziko Lapansi ndi patsiku
<%$<®3&<ty*£fo
Mulungu watibweretsa pano padziko lapansi kuti tiyesedwe mayeso
akulungama ndi kusalungama tsiku tomaliza lisanadze. Choncho tipirire ndi
kugwiritsa zimene Mulungu ndi Mtumiki Wake atiuza. Tidziwe kuti pali mavuto
pali zabwino.
Surat 22. Al-Hajj Juzu 17 706 ^ V ^jA-i
rr
g^ 5 j>"
la chimaliziro, Amange chingwe
kudenga, kenako Adzipachike
(ngati safuna kuona Chisilamu
chikufala); ndipo aone Kuti kodi
ndale zakezo zichotsa Zimene
zamkwiitsazo?
16. Momwemonso taitumiza
(Qur'an) kuti Ikhale mawu
omveka; ndipo ndithu, Mulungu
amaongola amene wamfiina.
17. Ndithu, amene akhulupirira,
ndi Amene ali m'chipembedzo cha
Chiyuda, Ndi chipembedzo cha
Sabia; ndi Akhrisitu, ndi Maajusi
(opembedza moto), Ndi
ophatikiza Mulungu ndi mafano,
Ndithu, Mulungu adzaweruza
pakati pawo Tsiku la chiweruziro
(Kiyama). (Osokera
Adzaponyedwa kumoto ndipo
olungama Adzalowetsedwa
kumunda wamtendere). Ndithu,
Mulungu ndi mboni pachinthu
Chilichonse.
18. Kodi suona kuti Mulungu
Zikumulambira zimene zili
Kumwamba ndi zimene zili
M'nthaka, kudzanso dzuwa,
Mwezi,nyenyezi mapiri, mitengo,
Nyama ndi anthu ambiri. Koma
ambirinso chilango chatsimikizika
Pa iwo. Ndipo amene Mulungu
wamuyalutsa, Palibe amene
angampatse ulemerero; ndithu,
Mulungu amachita chimene wafiina.
u®fcs$$&$&$&
Surat 22. Al-Hajj Juzu 17
707
>V^>»
rr
s^ 5 j>-
19. Awa ndi magulu awiri
amene akangana pa za Mbuye
wawo (pa zomwe zili zomuyenera,
ndi Zosamuyenera, ndipo ena
sadakhulupirire.) Choncho amene
sadakhulupirire, adzawadulira
Nsalu za kumoto ndi kuwaveka;
ndipo Pamwamba pa mitu yawo
padzathiridwa madzi Otentha.
20. Chifukwa chamadziwo
zidzasungunuka Zomwe zili
m'mimba mwawo Ndiponso
makungu (awo).
21. Ndipo (kuonjezera
pazimenezi) adzakhala nazo
Nyundo zachitsulo (zowamenyera.)
22. Nthawi iliyonse akafuna
kutuluka M'menemo, chifukwa
chakumva kupweteka,
Adzabwezedwa momwemo (ndipo
angelo uku Akuwamenya ndi
nyundo), ndi (kuwauza):
"Chilaweni chilango chootcha".
23. Ndithu, Mulungu
adzalowetsa amene Akhulupirira
ndi kumachita zabwino, Kuminda
ya mtendere komwe mitsinje
ikuyenda Pansi pake; m'menemo
akavekedwa (ndi Angelo) zibangili
za golide ndi ngale; Ndipo zovala
zawo m'menemo Zidzakhala za
veleveti.
24. Ndipo adzatsogozedwa
(kupita kumalo) Kokamba mawu
^»S*Wvi«
Surat 22. Al-Hajj Juzu 17
708
W tjA-i
1 1 gJ-1 5jj^»
abwino okhaokha; ndiponso
Adzatsogozedwa kunjira ya Mwini
Kutamandidwa (kunjira yonkera
ku Janna).
25. Ndithu, amene
sadakhulupirire (Mulungu Ndi
Mtumiki Wake) ndipo
nkumatsekereza Ena kunjira ya
Mulungu, (ndiponso
Nkumatsekereza kulowa) mu
Msikiti Wopatulika umene
tidauchita kuti ukhale Wa anthu
onse mofanana kwa amene
akukhala M'menemo ndi kwa
alendo, (anthu otere tidzawalanga
ndi chilango chaukali), Ndipo
aliyense wofiina kuchita zopotoka
M'menemo mosalungama,
timulawitsa Chilango chowawa
zedi.
26. Ndipo (kumbukira) pamene
tidamkhazika Ibrahim (ndi
kumlondolera) pamalo Pa Nyumba
(Yopatulikayo; tidamuuza Kuti):
"Usandiphatikize ndi chilichonse;
Ndipo iyeretse nyumba yanga
chifukwa Cha amene
akuizungulira ndi kumakhala
Pompo (pochita mapemphero
awo); ndi Omwe amawerama ndi
kugwetsa nkhope Zawo pansi. 1
e^lil^JtSiSdE
Mulungu akuuza Mtumiki Muhammad (SAW) kuti akambire opembedza
mafano zankhani ya Ibrahim yemwe iwo amati akumutsata pakupembedza
kwawo mafano ndi kuichita nyumba yopatulikayo kukhala nyumba
yopembedzera mafano kuti Ibrahim tidamulondolera pamalo anyumbayo ndi
Surat 22. Al-Hajj Juzu 17 [ 709 | \ V *£\
TY
^hy*
27. Ndipo (tidamuuza):
"Lengeza kwa Anthu za Haji;
akudzera (ena) oyenda Ndi
mapazi, ndipo (ena ali) pamwamba
pa Chiweto choonda (chiflikwa
chamasautso A paulendo); adza
kuchokera kunjira Zamtalimtali;
28. Kuti adzaone zabwino
zawo, ndikuti (Achulukitse)
kutchula dzina la Mulungu
m'masiku odziwika (ubwino
Wake), kupyolera m'zimene
wawapatsa Monga ziweto za
miyendo inayi. Ndipo Idyani ina
mwa nyamayo ndi kum'dyetsa
Wovutika, wosauka.
29. Kenako adziyeretse
kuzitakataka zawo, Ndipo
akwaniritse naziri (malonjezo)
Zawo ndikuzungulira nyumba
yakale."
30. Umo ndi momwe zikhalire;
ndipo amene Alemekeze zinthu
zopatulika za Mulungu Kutero ndi
bwino kwa iyeyo pamaso pa
Mbuye Wake. Ndipo ziweto za
miyendo inayi Nzovomerezeka
kwa inu kuzidya, kupatula Zomwe
zatchulidwa kwa inu (m'Qur'an
kuti Nzoletsedwa); choncho
<*>,
W5»
kumlamula kuti aimange ndikuti asandiphatikize pamapemphero ndi china
chilichonse, ndikuti aiyeretse nyumba Yanga kuuve wamafano ndi uve wina
uliwonse kuti pakhale pamaio pozungulira chifukwa choopa Mulungu. Nanga
bwanji iwo apasankha kukhala popembedzera mafano.
Surat 22. Al-Hajj Juzu 17
710
W *>i
YY
S^'JJ-
Upeweni uve wa mafano,Ndiponso
pewani mawu abodza,
31. Uku mutapendekera kwa
Mulungu Yekha, osati
kum'phatikiza (Mulungu). Ndipo
amene Akuphatikiza Mulungu Ndi
mafano, ali ngati wogwa
Kuchokera kumwamba, kenako
Mbalame nkumuwakha, kapena
Mphepo kukamtaya malo akutali.
32. Zimenezo ndikuti amene
alemekeze Zizindikiro za
chipembedzo cha Mulungu, kutero
ndichinthu choonetsa Kuopa
Mulungu m'mitima.
33. (Ziweto zimene
mukutumiza ku Makka monga
Nsembe) muli nazo zithandizo
mmenemo (Monga kuzikwera ndi
kuzikama mkaka) Kufikira nthawi
yodziwika, (yomwe ndi nthawi
Yozizingira); kenako malo
ozizingira ndi pafupi Ndi nyumba
yakalekaleyo.
34. Ndipo mpingo uliwonse
tidaupangira malo Ozingira
nsembe zamapemphero kuti
Atchule dzina la Mulungu pa
zomwe Wawapatsa monga ziweto
zamiyendo Inayi. Choncho
Mulungu wanu ndi Mulungu
m'modzi Yekha; gonjerani kwa
lye; Ndipo odzichepetsa auze
©i
9 * *S,S
6* *>'*> \"i^\\>S'S\'\ 9 i
Surat 22. Al-Hajj Juzu 17
711
w *>i
YT
«JM Sjj— »
nkhaniyabwino. 1
35. Omwe Mulungu
akatchulidwa, Mitima yawo
imanjenjemera ndiponso
Amapirira pazomwe zawapeza,
ndipo Amapemphera swala
moyenera Ndi kupereka chopereka
kuchokera m'zomwe Tawapatsa.
36. Ndipo ngamira (ng'ombe,
mbuzi ndi Mberere) tadzichita kwa
inu kuti zikhale Mwazizindikiro za
chipembedzo cha Mulungu;
m'zimenezo Muli zabwino kwa
inu; choncho Litchuleni Dzina la
Mulungu pa izo Pamene zikuima
mondanda (uku Mukuzizinga,)
ndipo zikagwa Cham'nthiti, idyani
(nyama yake) Ndikumdyetsa
yemwe Akungozungulirazungulira,
Wosapempha ndi wopempha
yemwe. Momwemo tazigonjetsa
kwa inu (Pochita kuti
zikugonjereni) Kuti muthokoze.
37. (Nyamazo) Mulungu
siimfika minofu yake Ngakhale
magazi ake, koma kuopa
kuchokera Mwa inu ndiko kumene
kumamfika; momwemo
Wazikhalitsa (nyamazo) zogonjera
inu kuti Mumlemekeze Mulungu
1 Tanthauzo la ndime iyi nkuti malamulo a za Haji sadaikidwe pa inu nokha
Asilamu, koma mpingo uliwonse wokhulupirira Mulungu adauikira malo ndi
malamulo operekera nsembe zawo kwa Mulungu kuti atamande dzina Lake
ndi kum'lemekeza pozinga nsembezo, monga kumthokoza lye pazimene
wawapatsa.
Surat 22. Al-Hajj Juzu 17
712
W*>l
YY
S^ l5 J>"
chifukwa Chakukuongolaniku.
Auze nkhani yabwino Ochita
zabwino.
38. Ndithu, Mulungu
amawateteza amene Akhulupirira,
ndithu, Mulungu sakonda Aliyense
wachinyengo, wosathokoza.
39. Chaperekedwa chilolezo
kwa (Asilamu) Amene akuputidwa
(ndi Adani awo kuti abwezere)
chifukwa chakuti iwo Achitiridwa
zoipa; ndipo ndithu, Mulungu
Ngokhoza kuwathandiza;
40. Omwe atulutsidwa
m'nyumba zawo popanda
Chilungamo, koma pachifiikwa
chakuti Akunena, "Mbuye wathu
ndi Mulungu. "Ndipo Pakapanda
Mulungu kukankha anthu ena
Kupyolera mwa ena, (popatsa ena
mphamvu Kuti agonjetse ena),
ndiye kuti Masinagogi,
Matchalitchi, nyumba Zina
zopemphereramo Ndi misikiti
momwe dzina la Mulungu
Likutchulidwa mochuluka
zikadagumulidwa. Ndithu,
Mulungu am'thangata amene
Akuthangata chipembedzo Chake;
ndithu, Mulungu Ngwanyonga,
Wogonjetsa chilichonse.
M'ndime iyi, Mulungu akuti akadawalekerera anthu oipa, omwe cholinga
chawo nkudzetsa chisokonezo padziko, popanda kusankha anthu ena kuti
alimbane nawo, ndiye kuti nyumba zopemphereramo Ayuda, Akhrisitu ndi
Asilamu, zikadagumulidwa. Koma Mulungu amasankha anthu olungama kuti
Surat 22. Al-Hajj Juzu 17
713
W *>i
Y Y g^l 5jj-»
41. Omwe akuti tikawakhazika
padziko Mwa ubwino, amachita
Mapemphero a swala Moyenera
ndi kupereka zakat, Ndi kulamula
zabwino ndi kuletsa zoipa; Ndipo
mabwerero a zinthu Nkwa
Mulungu basi.
42. Ndipo ngati akukuyesa
wabodza, (awa Akafiri,
sizachilendo), ndithu,
Adatsutsanso (aneneri awo)
patsogolo Pawo anthu a Nuhi,
Aadi, a Samudu,
43. Anthu a Ibrahima, anthu a
Luti,
44. Ndi anthu a ku Madiyani;
Nayenso Musa adayesedwa
Wabodza (adamkana). Ndipo
Osakhulupirira Ndidawapatsa
nthawi, Kenako ndidawathira
dzanja. Nanga Chidali bwanji
chilango changa.
45. Ndi midzi ingati
tidaiononga yomwe inkachita
Zoipa? Zipupa zitagwera pa
madenga ake. Ndipo ndi zitsime
(zingati) zomwe Zidasiidwa, ndi
nyumba zikuluzikulu Zomwe
zidali zolimba?
46. Kodi sayendayenda padziko
kuti akhale Ndi mitima (yanzeru)
9?} 9£ 99'9£ 9 " <i'/ 9 *< "\9*"'?>9iS
^as^aa
£'
&$%u&JM%£®
alimbane ndi anthu oipawo kuti choonadi cha Mulungu chisazime. Ndipo
amene akuteteza choonadi cha Mulungu, Chauta walonjeza kumthangata.
Surat 22. Al-Hajj Juzu 17
714
W*>i
YY
g^ 1 8 J>*
yowazindikiritsa Ndi makutu
omvera? Ndithu, maso Sagwidwa
khungu, (khungu loononga
Chipembedzo), koma mitima
yomwe ili M'zifiiwa ndi imene
imagwidwa khungu (Loononga
chipembedzo).
47. Ndipo akukufulumizitsa
kuti udzetse Chilango. Komatu
Mulungu sadzaswa Lonjezo lake
(limene adaliika lakuti Chilango
chenicheni chidzakhala patsiku La
chimaliziro). Ndipo ndithu, tsiku
Limodzi kwa Mbuye wako lili
ngati zaka Chikwi chimodzi
mukawerengedwe kanu.
48. Kodi ndi (anthu) amidzi
ingati amene Ndidawapatsa nthawi
pomwe ankachita Zoipa? Kenako
ndidawathira m'dzanja.Ndipo kwa
lye nkobwerera.
49. Nena: "E, inu anthu!
Ndithu, ine Kwa inu ndine
Mchenjezi woonekera:"
50. "Tsono amene akhulupirira
ndi kumachita Zabwino,
chikhululuko ndi riziki Laulemu
zili pa iwo."
51. "Ndipo amene akulimbika
Kulimbana ndi aya zathu, Iwo wo
ndi anthu a kumoto."
52. Ndipo palibe pamene
Tidatuma Mtumiki ngakhale
M'neneri patsogolo pako, koma
(J&9W9 &0& wSI^
Surat 22. Al-Haj j Juzu 1 7
715
W ^j*-i
n
g^ s j>"
Akamawerenga, satana amaponya
(Zosokoneza) m'kuwerenga
kwakeko; Koma Mulungu
amachotsa zomwe satana
Akuponya; kenako nkuzilongosola
aya Zake. Ndipo Mulungu
Ngodziwa Kwambiri, Wanzeru
zakuya.
53. (Izi zimachitika) kuti
achichite Chimene satana
akuponya kukhala Mayeso kwa
omwe m'mitima mwawo muli
Matenda ndi ouma mitima yawo;
ndithu, Osalungama ali
m'kusiyana komwe kuli Kutali
(ndi choonadi);
54. Ndipo kuti adziwe amene
apatsidwa Kuzindikira kuti
chimeneehi N'choonadi
chochokera kwa Mbuye Wako ndi
kuchikhulupirira ndikuti Mitima
yawo idzichepetse kwa lye;
Ndithu, Mulungu ndi Woongolera
ku Njira yolunjika amene
akhulupirira.
55. Ndipo amene
sadakhulupirire apitirira Kukhala
m'chikaiko ndi chimenecho
(Wadza nachocho) kufikira tsiku la
Chimaliziro liwadzera
mowatutumutsa, Kapena
chiwadzera chilango pa tsiku
Lopanda chabwino (kwa iwo).
56. Ufumu tsiku limenelo ngwa
Mulungu; adzaweruza
n, '%
@ *#
^%fe
h9 2£ZK"\
Surat 22. Al-Hajj Juzu 17
716
W $->!
t Y gJ-l 5jj-»
(mwachilungamo) Pakati pawo;
choncho amene Akhulupirira ndi
kumachita Zabwino, adzakhala
m'minda yamtendere.
57. Ndipo amene
sadakhulupirire (Mulungu Ndi
Mtumiki Wake) ndikutsutsa aya
Zathu, iwo adzapeza chilango
choyalutsa.
58. Ndipo amene asamuka
chifukwa cha Chipembedzo cha
Mulungu, kenako Ndikuphedwa
kapena kufa, ndithu, Mulungu
adzawapatsa (patsiku la
Chiweruzo) zopatsa zabwino.
Ndithu, Mulungu Ngwabwino
popatsa Kuposa opatsa.
59. Ndithu, adzawalowetsa
pamalo pom we Adzapayanja.
Ndithu, Mulungu Ngodziwa;
Ngodekha
60. Zimenezi zili chonchi,
ndipo yemwe Akubwezera kulanga
molingana ndi momwe lye
adalangidwira; kenakonso
nkuchitidwa Mtopola, ndithu,
Mulungu amthangata; Mulungu
Ngofufuta uchimo; Wokhululuka
Kwambiri.
61. Zimenezo nchifukwa
chakuti Mulungu Amalowetsa
usiku mu usana ndikulowetsa
Usana mu usiku, ndi chifukwanso
® &?*•■«
i^ia^^^tel^
'4>\&s$\a'J$\&
is£
Surat 22. Al-Hajj Juzu 17
717
W*>»
tt
g^ i5 J>^
Chakuti ndithu Mulungu
Ngwakumva Ngopenya.
62. Zimenezo nchifukwa
chakuti Mulungu ndi Wowona
(Alipo;) ndipo zimene
akuzipembedza Kusiya lye,
nzachabe. Ndipo Mulungu
Ngwapamwambamwamba
Ngwamkulu.
63. Kodi suona kuti Mulungu
amatsitsa Madzi kuchokera
kumitambo, ndipo Nthaka
imakhala yobiriwira? Ndithu,
Mulungu Ngodziwa zobisika
ndiponso Ngodziwa zoonekera.
64. Zakumwamba ndi zapansi
zonse Nzake; Ndithu, Mulungu
Ngwachikwanekwane;
Wotamandidwa.
65. Kodi sudaone kuti Mulungu
Wakufewetserani zonse
zam'nthaka Ndi zombo zomwe
zikuyenda panyanja Mwalamulo
Lake? Ndipo wagwira thambo Kuti
lisagwe panthaka koma kupyolera
M'chilolezo Chake; ndithu,
Mulungu Ngodekha kwa anthu
Ngwachifundo.
66. Ndipo lye ndi Amene
adakupatsani Moyo; kenako
adzakupatsani imfa, Ndipo kenako
adzakuukitsani; Ndithu, munthu
ngosathokoza .
©
$>
si&>
Surat 22. AI-Hajj Juzu 17 718 1 V *>»
Y T gJ-l 5j^
67. Mpingo uliwonse tidauikira
Machitidwe amapemphero omwe
Akuwatsata; choncho asatsutsane
Nawe pachinthu ichi, ndipo itanira
Anthu ku chipembedzo cha Mbuye
Wako. Ndithu, iwe uli
pachiongoko Chenicheni .
68. Ndipo ngati atsutsana nawe,
nena: "Mulungu Wodziwa koposa
zimene Mukuchita."
69. "Mulungu adzaweruza
pakati panu Tsiku la Kiyama
pazimene mudali Kusiyana."
70. Kodi sudziwa kuti Mulungu
akudziwa Zakumwamba ndi
zapansi? Ndithu, Zonsezo zili
m'kaundula (Wake), Ndithu,
(kudziwika kwa) zimenezo kwa
Mulungu nzosavuta.
71. Ndipo akupembedza
milungu yabodza, Kusiya
Mulungu, yomwe (Mulungu)
Sadaitumizire umboni wakuti
(Ipembedzedwe) yomwenso iwo
Sakuidziwa bwino. Ndipo anthu
Osalungama sadzakhala Ndi
owathandiza.
72. Koma aya zathu zomveka
Zikawerengedwa kwa iwo, uona
Kunyansidwa pankhope za Amene
sadakhulupirire. Ndipo amakhala
Pafupi kuwamenya amene
Amawawerengera aya zathu.
Nena: "Kodi ndikuuzeni zoipa
*Vi<9*i\' At 99 9 ' * $99"
©4*4 &&ito
Siirat 22. Al-Hajj Juzu 17
719
W *>i
YY
g^ 1 5 J>^
kwambiri Kuposa izi? Ndi moto
(Wa Mulungu) umene
wawalonjeza amene
Sadakhulupirire (Mulungu ndi
Mtumiki Wake) amenewo ndi
mabwerero oipa zedi."
73. E, inu anthu! Fanizo
laperekedwa; Choncho limvereni.
Ndithu, amene Mukuwapembedza
m'malo mwa Mulungu, Sangathe
kulenga ntchentche ngakhale
Atasonkhana (kuti athandizane)
Pachimenechi. Ndipo ngati
ntchenche Itawalanda chinthu,
sangathe kuchilanda
Kuntchentcheyo. Wafooka
kwenikweni Wopempha ndi
wopemphedwa.
74. Sadamlemekeze Mulungu,
kulemekeza Komuyenera. Ndithu,
Mulungu Ngwamphamvu
Ngogonjetsa chilichonse.
75. Mulungu amasankha
atumiki mwa angelo Ndi mwa
anthu. Ndithu, Mulungu
Ngwakumva; Ngopenya.
76. Akudziwa zimene zili
patsogolo pawo Ndi zimene zili
pambuyo pawo; kwa Mulungu
Yekha ndiko kobwerera Zinthu.
77. E, inu amene
mwakhulupirira! Weramani
ndikugwetsa nkhope zanu pansi
Ndipo mpembedzeni Mbuye wanu
o%K^S&^^t*olS
£- ?9 "1
9 * i} '*
Surat 22. Al-Hajj Juzu 17
720
W tjtr\
t T gj-l 5jj^»
Ndikuchita zabwino kuti
mupambane.
78. Ndipo menyerani
chipembedzo cha Mulungu,
kumenyera kwa choonadi; lye ndi
Amene adakusankhani (kuti
Mukhale mpingo wabwino;) ndipo
Sadaike pa inu zinthu zolemera
Pachipembedzo, ndi chipembedzo
Cha tate wanu Ibrahim. lye
(Mulungu) Adakutchani Asilamu
kuyambira kale (M'mabuku akale)
ndi mu iyi, (Qur'an) kuti Mtumiki
akhale mboni Pa inu, inunso kuti
mukhale mboni Pa anthu. Choncho
pempherani swala; Perekani zakat
ndipo gwirizanani Chifukwa cha
Mulungu. lye ndiye Mbuye wanu,
Mbuye wabwino zedi, Ndi
Mthandizi wabwino zedi.
Surat 23. Al-Mu'miniin Juzu 18
721
^A *>»
YT Oji*jll ^J-"
Surayi yayamba ndi kunenetsa zakupambana kwa
okhulupirira. Ndipo yatsatiza ndi kufotokoza mbiri zawo.
Kenako yafotokotoza chiyambi chakulengedwa kwa munthu ndi
maonekedwe osonyeza kukhoza kwa Mulungu
Wapamwambamwamba. Ndipo yatsatiza pankhaniyi nkhani za
aneneri zomwe zikuonetsa kuti uthenga wawo udali wofanana
ndikutinso anthu ngochokera kukholo limodzi.
Surayi yafotokoza za yemwe akufuna chiongoko ndi mwini
kusokera. Ndipo yasimbanso za maganizo a "Amshirikina" pa
za M'neneri Muhammad (Mtendere ndi Madalitso a Mulungu
zikhale pa iye). Ndipo Mulungu m'surayi wafunsamo mafunso
kuti anthu amuyankhe molingana ndi chilengedwe chawo.
Kenako surayi yasimba za momwe anthu adzakhalira pa tsiku
la Kiyama (Chimaliziro) ponenetsa kuti iwo adzaweruzidwa
mwachilungamo.
Surat 23. Al-Mu'minun Juzu 18 722 ^A t^ IT dyspoj^
Sural Al-Mu 'minim XXIII
M'dzina la Mulungu waChifundo
Chambiri, waChisoni.
1. Ndithu apambana
okhulupirira (Mwa Mulungu ndi
Atumiki Ake)
2. Amene amakhudzumuka
Pamapemphero awo (poipereka
mitima Yawo kwa Mulungu
modzichepetsa).
3. Ndi omwe amapewa zinthu
Zopanda pake (zachabe).
4. Ndi omwe amakwaniritsa
(Nsanamira ya) chopereka (Zakat).
5. Ndi omwe amasunga
umaliseche wawo.
6. Kupatula kwa akazi Awo ndi
adzakazi omwe Manja awo
akumanja apeza. Choncho iwo
(pakukumana ndi amenewo) Saali
odzudzulidwa
7. Koma omwe angafune
zosemphana ndi izi (Kulumikizana
ndi mkazi posiya njira Ziwirizi)
iwowo ndiwo opyola malire (A
Mulungu).
8. Ndi amene amasunga
malonjezo awo ndi Zomwe
akhulupirika nazo;
Ojfe&\<&&\&\j
^
&&#\?&\&
^^U^^SA
'? A'**'*®'
t&$a^&&&
Surat 23. Al-Mu'minun Juzu 18
723
\ A frji-l Y V O^pjil djj-*.
9. Ndi omwe akusunga
Mapemphero awo (popemphera
m'nthawi Zake ndi kutsata malamulo
ake uku Ali odzichepetsa).
10. Iwo ndi olandira (zabwino
tsiku la Kiyama).
11. Amene adzalandira Munda
wa Mtendere (Wotchedwa)
Fir'dausi (Munda Wapamwamba
kwambiri). M'menemo iwo
Adzakhala muyaya.
12. Ndipo ndithu, Tidamlenga
munthu Kuchokera ku dongo
labwino;
13. Kenako tidalenga ana ake
ndi dontho Lamadzi (Ambewu ya
munthu) lomwe Lidaikidwa
pamalo osungidwa;
14. Kenako tidalisintha
dontholo kukhala Magazi oundana;
ndipo kenako magaziwo
Tidawasintha kukhala m'nofu;
ndipo Kenako m'nofu tidausintha
kukhala Mafupa; ndipo mafupawo
tidawaveka Minofu, kenako
tidamsintha kukhala Cholengedwa
china. Choncho, watukuka
Mulungu, Wabwino polenga.
15. Kenako ndithu inu pambuyo
Pazimenezo mudzamwalira
16. Ndithu inu, kenako
mudzaukitsidwa Pa tsiku la
Kiyama.
(a\".'->,\\
©
"»-iiTi >''■
Surat 23. Al-Mu'minun Juzu 18
724 h A *>i
Tf Oj^jil &jj-»
17. Ndipo ndithu, tapanga njira
(mitambo) Zisanu ndi ziwiri
pamwamba panu, Ndipo
ndithu,(Ife) sitisiya kulabadira
Zolengedwa.
18. Ndipo tatsitsa madzi
mwamuyeso Kuchokera
kumwamba, ndi Kuwakhazikitsa
m'nthaka; ndipo ndithu Ife ndi
okhoza kuwachotsa (kuti
Musathandizike nawo koma
Sitidachite zimenezo chifukwa
Chokuchitirani chifundo).
19. Ndi madzi amenewo,
tidakupangirani Minda ya kanjedza
ndi mpesa, M'menemo inu
mulinazo zipatso Zambiri; ndipo
Mwazimenezo mumadya.
20. Ndipo (adakupangirani)
mtengo Womera paphiri la Sinai,
womwe Umatulutsa mafuta; ndipo
ndindiwo Kwa amene amadya.
(Mtengo wake ndi mzitona).
21. Ndipo ndithu, m'ziweto
Muli lingaliro kwa inu.
Timakumwetsani zomwe zili
m'mimba Mwake; ndipo
m'zimenezo mukupeza Zothandiza
zambiri; ndipo zina mwaizo
Mumadya.
22. Ndipo pa msana pa izo ndi
Pamwamba pazombo,
mumanyamulidwa.
<&tiffifolS@@x&>
©^
©;
*&MM9!&
Surat 23. Al-Mu'minun Juzu 18
725 hA *j*-i
YT J^»jil *jj***
23. Ndipo ndithu, tidamtuma
Nuhi kwa anthu Ake, ndipo adati:
"E, inu anthu anga! Mpembedzeni
Mulungu! Mulibe mulungu Wina
woti nkumpembedza kupatula lye.
Kodi simuopa (chilango Chake?)
24. Akuluakulu mwa anthu ake
amene Sadakhulupirire, adati:
"Uyu sali kanthu, Koma ndi
munthu ngati inu; akufuna kuti
Adzipezere ubwino pa inu; ndipo
Mulungu akadafuna
(kukuphunzitsani) Akadatuma
angelo. Zoterezi sitidamvepo
Kumakolo athu akale".
25. "Uyu sali kanthu, koma ndi
munthu Wamisala; choncho
muyembekezereni Mpaka nthawi
(yofera".)
26. (Nuhi) adati: "Mbuye
wanga; Ndipulumutseni pakuti
anditsutsa!"
27. Choncho
tidamuvumbulutsira (Mawu
Akuti): "Panga chombo
moyang'aniridwa
Ndikudziwitsidwa ndi Ife". Ndipo
Lamulo Lathu likadza
ndikufwamphuka Madzi muuvuni,
lowetsa mkati mwake
(Mwachombocho) chilichonse
Ziwiriziwiri, chachimuna ndi
chachikazi Ndi banja lako,
kupatula yemwe liwu Latsogola pa
'>JXs&*-*fi\>'<Si'L'
9 It*"
Surat 23. Al-Mu'minun Juzu 18
726 h A *>i
TT Oji^jll $jj->
iye kuti aonongeke mwa iwo.
Ndipo usandilankhule Za omwe
adzichitira (okha) zoipa Ndithu
iwo amizidwa (m'madzi).
28. Ndipo ukakhazikika
m'chombocho, iwe Ndi amene uli
nawo, nenani: "Tikuthokoza
Mulungu, amene Watipulumutsa
ku anthu Osalungama".
29. Ndipo (potsika),nena: "E,
Mbuye wanga! Nditsitseni;
kutsitsa kwa madalitso, Pakuti Inu
ndinu wotsitsa bwino kwambiri
Kuposa otsitsa".
30. Ndithu, m'zimenezi muli
zisonyezo. Ndithu, Ife tili (ndi
udindo) wowayesa ndi mayeso
Osiyanasiyana.
31. Kenako tidabweretsa
m'badwo wina pambuyo Pawo
(omwe ndi Adi).
32. Ndipo tidatuma kwa iwo
m'neneri (Hudu) Wochokera mwa
iwo, (yemwe ankati): "Pembedzani
Mulungu! Mulibe mulungu wina
Kupatula Iye. Kodi simuopa?
33. Ndipo akuluakulu a mwa
anthu ake amene Adali
osakhulupirira, ndikutsutsa za
Kukumana ndi tsiku la chimaliziro,
omwe Tidawapatsa kulemera
pamoyo wapadziko, Adati: "Uyu
saali kanthu, koma ndi Munthu
j.
r "' iz &iup, ». \ .?r „ < »a. "
Jk^ij
%^m*8<M>'oM
&
Surat 23. AI-Mu'minun Juzu 18
727
\ A ftjA-1 f V ji* jil 5jj--»
monga inu; amadya zimene inu
Mumadya, ndi kumwa Zomwe inu
mumamwa.
34. Koma ngati mumvera
Munthu wonga inu, Ndiye kuti
mukhala otaika (oluza).
35. Kodi akukulonjezani kuti
mukadzafa Ndikusanduka dothi
ndi mafupa, mudzaukitsidwanso
(m'manda)?
36. Sizingachitike,
sizingachitike, zimene
Mukulonj ezedwazi !
37. Palibe (moyo wina) koma
moyo wathu Wapadzikowu basi!
Tikufa ndiponso kukhala ndi
moyo! Ndipo sitidzaukitsidwa
M'manda.
38. Uyu saali kanthu (amene
akudzitcha Kuti ndi Mtumiki)
koma ndi munthu basi, Akupekera
Mulungu bodza, ndipo ife
S itimkhulupir ira. "
39. (Mtumikiyo) adati: "E,
Mbuye wanga! Ndipulumutseni
pakuti anditsutsa".
40. (Mulungu) adati:
"Posachedwapa akhala
Odandaula."
41. Choncho, mkuwe wa
(chilango) choonadi
Udawaononga, ndipo tidawachita
Ngati zinyalala (zongotengedwa
*$&&&#%&$&
%£&&%
%$.ofo$>Sic£> <M
%j&&$&$s
Surat 23. Al-Mu'minun Juzu 18
728
> A frji-l IT djsp 5jj~-
ndi madzi). Choncho, kuonongeka
kudatsimikizika Pa anthu
osalungama.
42. Ndipo titatero tidalenga
mibadwo ina Pambuyo pawo.
43. Palibe mtundu
Ungafulumizitse kapena
Kuichedwetsa nthawi yake yofera,
44. Kenaka tidatuma atumiki
Athu. Motsatizana; (wina pambuyo
pa mnzake). Ndipo m'badwo
uliwonse pamene adaufikira
Mtumiki wake, udamtsutsa; ndipo
Tidawaononga motsatana; ndipo
tidawachita Kukhala nkhani (za
anthu.) Ndipo kuonongeka
Kudatsimikizika pa anthu
osakhulupirira.
45. Zitatero tidatuma Musa ndi
m'bale wake Haaruna, pamodzi
ndi zozizwitsa Zathu, ndi Umboni
woonekera poyera,
46. Kwa Farawo ndi nduna
zake. Koma onse Adadzitukumula;
ndipo adali anthu odzikweza.
47.Ndipoadati:"Ha!
Tikhulupirire anthu awiri Onga ife,
omwe mtundu wawo ndi akapolo
Athu!".
48. Choncho adawatsutsa (onse
awiri), ndipo Adali m'gulu la
oonongedwa.
qCZ&^M$&&8&
Surat 23. Al-Mu'minun Juzu 18
729
>* ij±-\ rr o^jiiSj^
49. Ndipo ndithu, Musa
Tidampatsa Buku kuti iwo
Aongoke.
50. Ndipo tidamchita mwana
wa Mariamu ndi mayi wake
kukhala Chisonyezo (choonetsa
Kukhoza kwathu). Ndipo
tidawapatsa malo Othawirapo,
pachikweza, chokhazikika
Pomwenso padali akasupe.
51. E, inu Atumiki! Idyani
Zakudya zabwino, Ndipo chitani
zabwino. Ndithu, Ine ndi Wodziwa
Zonse zimene muchita.
52. (Tidauza mibadwo yawo):
"Ndithu mpingo Wanuwu ndi
mpingo umodzi, ndipo Ine Ndine
Mbuye wanu; choncho ndiopeni".
53. Koma adadula chinthu
chawochi (Chipembedzo chawo)
pakati pawo M'mipatukomipatuko;
gulu lililonse Limasangalalira
chimene lili nacho.
54. Choncho, asiye mu umbuli
wawo kufikira Nthawi (yakufa
kwawo).
55. Kodi akuganiza kuti
Tikamawapatsa chuma Ndi ana,
56. Tikuwafiilumizitsira
zabwino. Sichoncho, koma Iwo
sakuzindikira.
57. Ndithu, amene amakhala
amantha chifukwa Choopa Mbuye
P®4$J&S&&
Surat 23. Al-Mu'minun Juzu 18
730
Sh *j*-l
V T 0^j» jil 5jj~*
wawo, (ndim'mene mathero Awo
adzakhalire);
58. Ndi omwe amakhulupirira
aya za Mbuye Wawo;
59. Ndi omwenso saphatikiza
Mbuye wawo ndi Mafano;
60. Ndi omwenso amapereka
(zakaati ndi sadaka Kuchokera
m'chuma) chimene apatsidwa,
Uku mitima yawo ili yoopa kuti
adzabwerera Kwa Mbuye wawo;
61. Amenewa ndiamene
akuchita changu Pa zinthu
zabwino, ndipo iwo akutsogolera
(Ena) pazimenezo.
62. Ndipo sitikakamiza munthu,
koma chimene Angathe
(kuchichita). Ndipo tili naye
Kaundula (wosunga chilichonse)
yemwe Adzayankhula choonadi
ndipo iwo Sadzaponderezedwa
63. Koma mitima yawo ili
Nkusalabadira mu ichi; Ndipo iwo
ali ndi Ntchito zimene akuchita,
Osati izi,
64. Kufikira tikadzawaika
m'chilango amene ali Opeza
bwino, pompo adzakuwa
(ndikupempha Chipulumutso).
65. (Kudzanenedwa kwa iwo):
"Musalire lero (Ndikupempha
chipulumutso)! Ndithu, inu
Simupulumutsidwa ndi Ife.
%&9&&$m
Surat 23. AI-Mu'minun Juzu 18
731
^A *>1
Yf Uji^jll 3jj-*»
66. "Ndipo aya Zanga
zinkawerengedwa kwa Inu koma
munkazibwezera kumbuyo
Ndizidendene zanu,
67. Uku mukudzikweza;
Nkumakambirana usiku
Zachabechabe zoinyoza (Qur'an)"
68. Kodi sadaganizire liwu (ili
limene wadza Nalo
Mtumiki{SAW}), kapena
zawadzera Zomwe
sizidawadzerepo makolo awo
Akale?
69. Kodi kapena sadam'dziwe
Mtumiki wawoyu (Makhalidwe
ake) kotero kuti iwo Akum'kana?
70. "Kapena akunena Kuti
ngwamisala?" Koma Wawadzera
ndi choonadi, Ndipo ambiri aiwo
Amachida choonadi.
71. Ndipo choonadi
Chikadatsatira zofuna Zawo, ndiye
kuti thambo Ndi nthaka ndi za
m'menemo Zikadaonongeka!
Koma Tawabweretsera
chikumbutso chawo, koma Iwo
akuchipewa chikumbutso
chawocho.
72. Kodi kapena ukuwapempha
malipiro (Nchifukwa chake
akuchikana Chipembedzochi)?
Koma malipiro a Mbuye Wako
ndiwo abwino; lye ndi Wopereka
Wabwino kuposa opereka.
%&J"p&jfi&-
Surat 23. Al-Mu'minun Juzu 18
732
> A *ji-i Y T dji*£\ djj--
73. Ndipo ndithu, iwe
ukuwaitanira kunjira Yolunjika;
(supempha malipiro kwa iwo Pa
kuitanako).
74. Ndipo ndithu, amene
sakhulupirira tsiku La chimaliziro,
ali kutali ndi njira Ya choonadi.
75. Ndipo tikadawachitira
Chifundo ndi kuwachotsera
Masautso omwe ali nawo, Ndithu,
akadapitiriza Kuyumbayumba
M'kuchita kwawo zoipa.
76. Ndipo ndithu, Tidawalanga
ndi chilango Chaukali, koma
sadacheukire kwa Mbuye wawo
ndikudzichepetsa,
77. Kufikira pamene
Tidawatsekulira khomo la
Chilango chaukali; Pamenepo
ndipo Adataya mtima.
78. Ndipo lye ndi Yemwe
adakupangirani Makutu, maso ndi
moyo; Nzochepa zimene
Mukuthokoza.
79. Iyenso ndi Yemwe
Wakufalitsani padziko;Kenako
mudzasonkhanitsidwa kwa lye.
80. Ndipo lye ndi Yemwe
Amapatsa moyo ndi Imfa,ndipo
kusinthana Kwa usiku ndi usana
Nkwake. Kodi simuzindikira?
81. Koma akunena monga
(anthu) oyamba Adanenera.
#iM^^
0,
K£B(W&*\$S&
Surat 23. Al-MiTminun Juzu 18 733 I > A ^jJb-i Y r 0>^ jii 5jj--
82. Akunena: "Kodi tikadzafa
ndikukhala Dothi ndi mafupa,
tidzaukitsidwanso?"
83. " Ndithudi ife ndi makolo
athu kale Tidalonjezedwa zimenezi
izi sikanthu koma Nkhambakamwa
za anthu akale."
84. Nena: "Kodi nthaka njayani
ndi zomwe zili M'menemo, ngati
inu Mukudziwa (kanthu)!"
85. Adzanena kuti, "Nza
Mulungu!" Nena: "Nanga bwanji
simukumkumbukira(Kuti lye
Ngokhoza chilichonse)?
86. Nena: "Kodi ndani Mbuye
wa thambo zisanu Ndi ziwiri, ndi
Mbuye wa Mpando Waukulu?"
87. Anena (kuti): "Nza
Mulungu." Nena: "Nanga bwanji
simukumuopa?"
88. Nena: "Kodi ndani Yemwe
m'manja Mwake Muli mphamvu
yolamulira chinthu Chilichonse?
Ndipo lye amateteza zonse. Ndipo
palibe chimene Chingatetezedwe
kuchilango Chake. Ngati inu
mukudziwa."
89. Anena (kuti): "Ndi
Mulungu." Nena: "Nanga
mukulodzedwa Bwanji (ndi satana)?
90. Koma tawabweretsera
choonadi; ndithu iwo Ngabodza
(potsutsana ndi choonadicho).
®G>$&n&&$%
{j$\^ffity$\&&&
® t
®(yyW^I^V^w51fe -
®(lJj^(J\9(^^i)t>pyi~'
<^#£&V$&Ci
Surat 23. Al-M u'minun Juzu 18 734 \A *>■»
TV o^*jli 3j^»
91. Mulungu sadadzipangire
mwana, ndipo Padalibe pamodzi
ndi lye mulungu (wina), Ngati
zikadakhala choncho ndiye kuti
mulungu Aliyense akadatenga
zimene Adalenga, ndipo milungu
ina ikadaipambana Milungu
inzawo (polimbanirana ufumu)
Mulungu wapatukana nazo
kwambiri zimene Akusimbazo.
92. Wodziwa zamseri ndi
Zapoyera; watukuka Kuzimene
akumphatikiza nazozo.
93. Nena: "E, Mbuye wanga!
Ngati mungandionetse zomwe
Akulonjezedwa (ndikadali ndi
moyo),
94. E, Mbuye wanga!
Musandikhazike M'gulu la anthu
osalungama".
95. Ndipo ndithu, Ife
ndiWokhoza kukuonetsa
(Chilango) chimene Tikuwalonjeza.
96. Chotsa zoipa (zimene
akukuchitira) Powabwezera
zabwino; Ife tikudziwa Zimene
akunena.
97. Ndipo nena: "E, Mbuye
wanga! Ndikudzitchinjiriza ndi inu
Kumanong'onong'o a satana.
98. "Ndiponso
ndikudzitchinjiriza ndi inu Mbuye
Wanga kuti asandidzere."
v$z&&^&
t '9%> V
*$\4&^&C
JL
®,
Surat 23. Al-Mu'minun Juzu 18
735
\ A * ji-l V T djv>£\ Ojj~*
99. Kufikira m'modzi wawo
ikam'dzera imfa, Amanena:
"Mbuye wanga! Ndibwezereni (Ku
moyo wa padziko),
100. Kuti ndikachite zabwino
pazimene Ndidasiya." (Angelo
amayankha kuti): "Iyayi! Ndithu,
awa ndi mawu basi Amene iye
akulankhula (imfa Ikamfika)."
Ndipo patsogolo pawo Pali
chiyembekezo; (moyo
Wamasautso kwa oipa; ndipo
wamtendere Kwa abwino) kufikira
tsiku limene Adzaukitsidwa.
101. Choncho, lipenga
likadzaimbidwa, Sipadzakhala
chibale Pakati pawo tsiku
Limenelo, ndipo Sadzafunsana.
102. Tsono omwe mlingo (wa
zochita zawo Zabwino)
udzalemere, iwowo ndiwo
Opambana,
103. Ndipo omwe miyeso yawo
(yazochita Zabwino) idzatsike,
iwowo ndi omwe Adadziluzitsa
okha; adzakhala ku Jahannama
Muyaya .
104. Moto ukawawula nkhope
zawo, ndipo Adzakhala m'menemo
Uku akukukuta (mano).
105. (Adzauzidwa): "Kodi aya
Zanga Sizidali kuwerengedwa kwa
inu ndipo inu Nkumazitsutsa?"
%20
Surat 23. Al-Mu'minun Juzu 18
736
\ A * j£-l Y T O^i* jil 5 j j-j
106. Adzati: "Mbuye wathu!
Zoipa zathu Zidatigonjetsa,
choncho tidali anthu Osokera.
107. Mbuye wathu! Titulutseni
umu (M'moto ndikutibwezera
kudziko lapansi Kuti tikachite
ntchito yabwino); Ngati
titabwerezanso kuchita zoipa,
Ndiye kuti tidzakhaladi oipa
Odziononga tokha."
108. (Mulungu) adzati:
"Khalani chete m'menemo,
Monyozeka! Ndipo
musandilankhule !
109. Ndithu, mwa akapolo anga
lidalipo gulu Lomwe linkanena:
"Mbuye wathu! Takhulupirira;
choncho tikhululukireni
Ndikutichitira chifundo; ndipo inu
Ngabwino kwambiri kuposa (ena
onse) Ochita chifundo."
110. "Koma inu mudawachita
Chipongwe kufikira
Adakuiwalitsani kundikumbuka
Uku muli kuwaseka."
111. "Ndithu, Inelero
ndawalipira (munda Wa mtendere)
chifukwa cha kupirira Kwawo;
ndithu, iwo ndiwo opambana."
112. Adzanena: "Kodi
mudakhala Nthawi yotani padziko
Pachiwerengero cha zaka?"
*^^<s»®gfts
©I
x **f^ \49<*
ty&Sty&MZ
©u£$$j3t
Surat 23. AI-MiTminun Juzu 18
737 > A frj£-l XT Opjil 5jj*.
113. Adzayankha: "Tidakhala
tsiku limodzi Kapena gawo la
tsiku; (adzatero poyerekeza
Ndikutalika kwa moyo
wamasautso kumoto); Afunse
owerengera."
114. Adzanena: "Inu
simudakhale (kudzikoko) Koma
pang'ono basi, mukadakhala
Mukudziwa (chilango chomwe
Chakufikanichi, sibwenzi
mukuchita zoipa).
115. "Kodi mumaganiza Kuti
tidakulengani chabe, Ndikuti
simdzabwezedwa kwa Ife?"
116. Watukuka Mulungu,
Mfumu ya Choonadi; palibe
wompembedza Mwachoonadi
koma lye, Bwana Wa Mpando
Wolemekezeka (Kwambiri).'
117. Ndipo amene apembedza
mulungu wina Pomphatikiza ndi
Mulungu (weniweni),
Chikhalirecho iye alibe umboni
Pazimenezo; basi chiwerengero
chake Chili kwa Mbuye wake.
Ndithu, Osakhulupirira
sangapambane.
118. Choncho nena: "Mbuye
wanga! Ndikhululukireni
ndikundichitira Chifundo! Inu
Ngabwino kuposa achifundo."
Surat 24. An-Niir Juzu 18
738
1A ftji-1
1 1 jjJl ^JJ- -
Msurayi Mulungu wafotokoza zakufunika koyeretsa mtundu
kumachitidwe a chiwerewere. Ndipo surayi ikuletsa kufalitsa
zoipa pakati pa Asilamu, ndikukhazikitsa zilango kwa anthu kuti
machitidwewa alekeke. Ndipo yafotokozanso miyambo
yokhalirana pakati pa Asilamu pamoyo wawo -monga kuodika
polowa mnyumba, ndikuzolitsa maso, ndikusunga umaliseche.
Ndiponso kuti amuna ndi akazi amene sali anyazi,
asamasanganikirane .
Surayi yafotokozanso zofunika pabanja la chisilamu-monga
kudzipatsa ulemu, kudziyeretsa kumachitidwe osayenera
ndikukhala wolungama nthawi zonse.
Surat 24. An-Nur Juzu 18
739
^A *>i
1 i jjJt Oj^-
SuratAl-NurXXIV
M'dzina la Mulungu waChifundo
Chambiri, waChisoni.
1. Iyi ndi sura; Taivumbulutsa,
ndipo Taikamo Malamulo. Ndipo
m'menemo Tatumizamo aya
zomveka kuti Mukumbukire
(malamulo ndi Kuchita nawo
m'njira Yoyenera).
2. Mkazi wachiwerewere ndi
mwamuna wa Chiwerewere
aliyense wa iwo mkwapuleni
Zikoti zana limodzi (100).
Musagwidwe chisoni ndi iwo pa
Chipembedzo (malamulo) cha
Mulungu, ngati inu
mukukhulupiriradi Mwa Mulungu
ndi tsiku la chimaliziro. Ndipo
gulu la Asilamu lionerere Chilango
cha iwo.
3. Mwamuna wa chiwerewere
sakwatirana Ndi mkazi (wabwino)
koma Wachiwerewere mnzake,
kapena mkazi Wopembedza
mafano. Nayenso mkazi
Wachiwerewere sakwatirana ndi
Mwamuna (wabwino) koma
wachiwerewere Mnzake, kapena
wopembedza mafano. Ndipo
zimenezi zaletsedwa kwa Asilamu.
4. Ndipo amene akunamizira
akazi Odziteteza (powanamizira
o^l^jll^U.
-a
W^*UisJJb
Surat 24. An-Nur Juzu 18
740 I > A *>i
1 1 j>Jl 5j^
kuti Achita chiwerewere), ndipo
osabwera nazo Mboni zinayi,
akwapuleni zikoti 80; Ndiponso
musauvomereze umboni wawo
Mpaka kalekale. Iwo ngotuluka
M'chilamulo cha Mulungu,
5. Kupatula amene alapa
pambuyo Pazimenezo, ndipo
nkukonza (zochita Zawo), Ndithu,
Mulungu Ngokhululuka;
Ngwachisoni, (awakhululukira).
6. Ndipo amene akunamizira
akazi awo (kuti achita
chiwerewere) ndipo Iwo nkukhala
opanda mboni, koma (Iwo) okha,
choncho umboni Wa mmodzi wa
iwo (umene Ungamchotsere
chilango chomenyedwa Zikoti 80),
ndikupereka umboni Kanayi
polumbirira Mulungu kuti ndithu,
lye ndi mmodzi mwa onena zoona;
7. Ndipo kachisanu (alumbire)
kuti Matemberero a Mulungu
akhale pa iye Ngati (iye) ali
m'modzi mwa onama.
8. Ndipo (mkazi) chilango
amchotsera Atapereka umboni
kanayi polumbirira Mulungu kuti
(uyu mwamuna) ndi mmodzi mwa
onama.
9. Ndipo kachisanu (alumbire)
kuti Mkwiyo wa Mulungu ukhale
pa iye Ngati (mwamuna wake) ali
mmodzi Mwa onena zoona.
&{£ IV*
3BteWy>^6foJ*K
"safe
Q)f>- \ U '
(&,^(y*.
Surat24. An-Nur Juzu 18 I 741 I > A *>H
T £ jjJl $jj-*>
10. Ndipo pakadapanda ubwino
wa Mulungu ndi Chifundo chake
pa inu (mukadavutika). Ndipo
Ndithu, Mulungu Ngolandira
kulapa; . Wanzeru zakuya.
11. Ndithu, amene adza ndi
bodza (Ponamizira Mayi Aisha,
yemwe ndi Mkazi wa Mtumiki,
kuti wachita Chiwerewere), ndi
gulu la mwa inu. Musaganizire
zimenezo kuti nzoipa Kwa inu,
koma kuti zimenezo nzabwino
Kwa inu. Ndipo munthu aliyense
Waiwo apeza (chilango)
pamachimo Amene wawachitawo.
Ndipo yemwe Wasenza gawo
lalikulu lauchimowo Mwa iwo,
adzapeza chilango chachikulu
12. Nanga bwanji pamene
Mudaimva (nkhani) Iyi Asilamu
achimuna Ndi Asilamu achikazi
Sadaganizire anzawo zabwino
Ndikunena kuti: "Hi ndi bodza
loonekera?"
13. Nanga bwanji sadabweretse
mboni Zinayi (pazimenezi)? Ndipo
pamene Alephera kubweretsa
mboni, iwo Ngabodza kwa
Mulungu.
14. Ndipo pakadapanda ubwino
wa Mulungu Ndi chifundo chake
pa inu, padziko Lapansi ndi
patsiku lachimaliziro, Chilango
chachikulu chikadakukhudzani Pa
zomwe munkazijijirikira.
%\8^$sw&8&
fiW^&f
Siirat 24. An-Nur Juzu 18
742 |1A »>i
Y t jy i\ oj^
15. Pamene mudalilandira
(bodzalo) ndi Malirime anu ndi
kumanena ndi milomo Yanu
zomwe inu simukuzidziwa, ndipo
Mumaganizira kuti ndi chinthu
Chochepa pomwe icho kwa
Mulungu Ndi chinthu chachikulu.
16. Ndipo nanga bwanji pamene
mudalimva (Bodzalo) simudanene
(kuti): "Sikoyenera kwa ife
kulankhula izi; Kuyera nkwanu
(Mbuye wathu). Hi Ndi bodza
lalikulu."
17. Mulungu akukulangizani
kuti: "Musabwerezenso kuchita
zonga Zimenezi mpaka kalekale,
ngati inu Muli okhulupirira
enieni."
18. Ndipo Mulungu
akukufotokozerani Aya Zake
mwatsatanetsatane. Ndipo
Mulungu Ngodziwa; Ngwanzeru
zakuya.
19. Ndithu, amene akukonda
kuti Zoipa zifale pa amene
akhulupirira, Chilango chowawa
chili pa iwo Padziko lapansi ndi
patsiku la Chimaliziro. Ndipo
Mulungu ndi Yemwe akudziwa
(zoyenerana ndi Inu), koma inu
simudziwa.
20. Ndipo pakapanda ubwino
wa Mulungu Ndi chifundo chake
pa inu, (Pakadapezeka zauve).
efcr
4&&ti£M®W&
wz®%g&M&&
Surat 24. An-Nur Juzu 18
743
>A tf-jA-i
t £ j>Ji 5j>-
Koma ndithu, Mulungu Ngofatsa;
Ngwachifundo.
21. E, inu amene
mwakhulupirira, Musatsatire
mapazi a satana. Ndipo amene
atsatire Mapazi a satana (asokera)
ndithudi lye akulamula zauve ndi
zoipa. Ndipo Pakapanda ubwino
wa Mulungu ndi Chifundo chake
pa inu, sakadayera Aliyense mwa
inu mpaka kalekale. Koma
Mulungu amamuyeretsa amene
wamfuna. Ndipo Mulungu
Ngwakumva zonse; Wodziwa
kwambiri.
22. Ndipo ochita zabwino
(padziko Lapansi), ndiponso eni
kupeza Bwino mwa inu,
asalumbire kuti Aleka kupatsa
achinansi, Masikini, ndi osamuka
panjira Ya Mulungu. Koma
Akhululuke Ndikuleka zimenezo.
Kodi Simufuna kuti Mulungu
Akukhululukireni? Mulungu
Ngokhululuka
kwambiri .Ngwachisoni (Choncho,
nanunso teroni).
23. Ndithu, amene akunamizira
akazi Oyera (kumachitidwe
Achiwerewere), odziteteza
Kumachitidwe oipa, okhulupirira,
Atembereredwa padziko lapansi
ndi Patsiku la chimaliziro. Ndipo;
Chilango chachikulu chili pa iwo;
Surat 24. An-Nur Juzu 18
744 h A *j*->
Y i jjJt Sjj-*>
24. Tsiku lomwe malirime awo,
mikono Yawo ndi miyendo yawo
zidzawachitira Umboni pazomwe
adali kuchita.
25. Tsiku limenelo Mulungu
Adzawapatsa mphotho yawo ya
choonadi, Ndipo adzadziwa kuti
Mulungu ndiye Mwini kulipira
kwachoonadi Koonekera poyera.
26. Akazi oipa ndi Aamuna
oipa, naonso Amuna oipa ndi
aakazi Oipa; ndipo akazi abwino
Ndi aamuna abwino, Naonso
amuna abwino ngaakazi abwino.
Iwowa ngopatulidwa kuzimene
akunenazo. I wo adzapeza
chikhululuko ndi riziki Laulemu
(ku Munda wa Mtendere).
27. E, inu amene
mwakhulupirira! Musalowe
m'nyumba zomwe Sinyumba zanu
kufikira mutapempha Chilolezo
poodira ndikupereka Salaamu kwa
eni nyumbazo. Kutero ndi kwa
Bwino kwa inu kuti mukumbukire
(Nkuona kuti zomwe mukuuzidwa
Nzabwino).
28. Koma ngati simupeza
munthu aliyense M'menemo,
musalowe kufikira Mutapatsidwa
chilolezo. Ndipo Mukauzidwa
kuti: "Bwererani, Bwererani;
chimenechi nchokuyeretsani.
Ndipo Mulungu akudziwa Zimene
muchita.
%
Sfirat 24. An-Nur Juzu 18
745
>A *>»
T t jjA\ t^
29. Sikulakwa kwa inu kulowa
m'nyumba Zosakhalidwa, (monga
sitolo, hotela; Popanda chilolezo),
momwe muli Zokuthandizani;
ndipo Mulungu Akudziwa zomwe
mukuonetsera poyera Ndi zimene
mukubisa.
30. Auze Asilamu achimuna
kuti adzolitse Maso awo
(asayang'ane zoletsedwa), Ndipo
asunge umaliseche wawo. Ichi
Nchoyera kwambiri kwa iwo.
Ndithu, Mulungu akudziwa nkhani
za zonse Zomwe achita.
31. Ndipo auze Asilamu
achikazi kuti adzolitse Maso awo,
ndikusunga umaliseche wawo,
Ndipo asaonetse (poyera) zomwe
Amadzikongoletsa nazo kupatula
zimene Zaonekera poyera
(popanda cholinga Chotero).
Ndipo afunde kumutu mipango
Yawo mpaka m'zifuwa zawo;
ndipo asaonetse Poyera
zodzikongoletsa nazo koma kwa
Amuna awo, kapena atate awo,
kapena Apongozi awo, kapena ana
awo, kapena ana A amuna awo,
kapena abale awo, kapena ana A
abale awo, kapena ana a alongo
awo, Kapena akazi anzawo
(achisilamu). Kapena Yemwe
wapatidwa ndi dzanja lamanja
(Monga kapolo), kapena otsatira
(antchito) Omwe ndi amuna
Surat 24. An-Nur Juzu 18
746
^A frjJUi
Y t j>3» 5j>*
opanda zilakolako za akazi Ndi
ana omwe sadziwa za ukazi. Ndipo
Asamenyetse miyendo yawo
(pansi) kuti Zidziwike zimene
akubisa mwa zomwe
Amadzikongoletsa nazo.
Tembenukirani Kwa Mulungu,
nonse inu okhulupirira Kuti
mupambane.
32. Ndipo zikwatitseni mbeta za
mwa inu (mfulu), Ndi akapolo anu
amene ali abwino (achimuna) Ndi
adzakazi anu. Ngati ali osauka
Mulungu Awalemeza kuchokera
m'zabwino Zake. Ndipo Mulungu
za ufulu Zake nzambiri (Zopanda
muyeso,ndiponso), Ngodziwa
Kwabasi.
33. Ndipo amene sapeza
chokwatirira Apewe (uve wa
chiwerewere) kufikira Mulungu
atawalemeza ndi zabwino Zake.
Ndipo amene afuna kuti
awalembere (kuti Apate ufulu)
mwa amene Manja anu akumanja
apeza, alembereni (Kuti
adziombole). Ngati mwaona
Zabwino mwa iwo apatseni gawo
La chuma cha Mulungu chomwe
akupatsani. Musawakakamize
adzakadzi anu kuchita uhule Ngati
akufuna kudzisunga, ncholinga
choti Mupeze zinthu zamoyo
wadziko lapansi. Ndipo amene
angawakakamize, ndithu Mulungu,
Surat 24. An-Nur Juzu 18
747
>A *>»
Y t j>Jt ojj^
pambuyo Pokakamizidwa
kwawoko, Ngokhululuka;
Ngwachisoni (Kwa
okakamizidwawo) .
34. Ndipo ndithu,tatumiza Kwa
inu aya zofotokoza (Zofunika
zonse) mwatsatanetsatane, Ndi
mafanizo (okuphanulani maso) Pa
za amene adamuka patsogolo
panu, Ndi phunziro kwa oopa
(Mulungu).
35. Mulungu nkuunika kwa
kuthambo ndi Nthaka. Fanizo la
kuunika kwake (Powaongolera
akapolo ake) lili ngati "Mishikati"
(chibowo cha pa khoma choikapo
Nyali) yomwe mkati mwake
mwaikidwa nyali. Nyali ili
m'galasi. Ndipo galasilo lili ngati
Nyenyezi yowala.Nyali imeneyo
imayatsidwa Ndi mafuta ochokera
kumtengo wodalitsidwa Wa
mzitona, womwe suli mbali
yakuvuma Ngakhale kuzambwe;
(umamenyedwa Kwambiri ndi
dzuwa pamene likutuluka, Ndi
pamene likulowa.) Mafuta ake
Ngoyandikira kukuwala okha
(chifukwa Champhamvu yake),
ngakhale moto Usanawakhudze.
Kuunika pamwamba pa Kuunika!
Mulungu amamuongolera kuunika
Kwake amene wamfuna. Mulungu
amaponya Mafanizo kwa anthu
(kuti aganizire ndi Kupeza
6®W
}&2J £*• 1>*& <&^j£
Surat 24. An-Nur Juzu 18
748
>A *>l
T £ jj-Ji Sj^-"
phunziro) Mulungu ngodziwa
Chilichonse.
36. (Apezeke akupemphera
kasanu) m'nyumba Zomwe
Mulungu walamula kuti
Zilemekezedwe; ndipo M'menemo
dzina Lake Litchulidwe;
azimulemekeza m'menemo
(M'misikiti) kum'mawa ndi
kumadzulo;
37. Anthu omwe malonda
Ogulitsa ndi kugula
Sawatangwanitsa posiya
Kukumbukira Mulungu ndi
Kupemphera (swala) ndi kupereka
Chopereka (zakaat). Amaopa tsiku
lomwe Mitima ndi maso
zidzasinthika;
38. Kuti Mulungu adzawalipire
Zabwino pa zomwe Adachita ndi
kuwaonjezera Zabwino Zake.
Ndipo Mulungu Amampatsa
amene wamfuna Popanda
chiwerengero.
39. Ndipo amene
sadakhulupirire, ntchito zawo
(Zimene akuziona ngati zabwino)
zidzakhala Ngati zideruderu
m'chipululu chamchenga;
Waludzu nkumaganizira kuti
ndimadzi; ndipo Akapita
pamenepo, osaonapo chilichonse.
(Nawonso pomwe adzadza
kuzochita zawo Zabwino patsiku la
V*if ^^"A^ 9 \k
TO^^3&6fe&
'&':'l\$X'\tf>"!'>
P&ir**.
Surat 24. An-Nur Juzu 18
749
1A *j£-i
T £ jj-y' *jj-"
Kiyama sadzapeza Mphotho
iliyonse, chifukwa chakuti
Adachimenya nkhondo
Chisilamu). Ndipo Adzapeza
Mulungu kumeneko, ndipo
Adzamkwaniritsira chiwerengero
chake Ndipo Mulungu
Ngwachangu Powerengera.
40. Kapena (ntchito zawo
zoipazo) zili ngati M'dima mkati
mwanyanja yamadzi ochuluka
Yomwe yaphimbidwa ndi
mafunde, ndipo Pamwamba
pamafundewo pali mafundenso.
Ndiponso pamwamba pake
(mafundewo) Pali mitambo.Ndipo
m'dima uwu pamwamba Pa
m'dima uwu. Ndipo akatulutsa
mkono Wake, sangathe kuuona
(chifukwa Chakuchindikala kwa
m'dima). Ndipo amene Mulungu
sadampatse kuunika, sakhala nako
Kuunika.
41. Kodi suona kuti zonse
zopezeka kumwamba Ndi pansi
zikumulemekeza Mulungu,
kudzanso Mbalame zikatambasula
mapiko awo (Ngakhalenso
zikapanda kutambasula)
Chilichonse (mwazimenezo)
chikudziwa Pemphero lake ndi
m'mene Chingamulemekezere
(Mulungu wake). Ndipo Mulungu
Ngodziwa Zonse zimene akuchita.
Surat 24. An-Nur Juzu 18
750 I > A «-j*-i
y t jy }\ ij^
42. Ufumu wakumwamba ndi
pansi, ngwa Mulungu (yekha);
ndipo kobwerera kwa Zonse nkwa
Mulungu.
43. Kodi suona kuti Mulungu
akuyendetsa Mitambo, kenako
nkuikumanitsa pamodzi, Ndipo
kenako nkuikhazika m'milumilu?
Nuona mvula ikutuluka pakati pa
iyo. lye Akutsitsa mapiri
amitambo kuchokera Kumwamba
momwe muli mvula yamatalala;
Ndipo amamenya nawo Amene
wamfuna, ndikumpewetsa Amene
wamfuna. Kung'anima kwake
Kumayandikira kuchititsa Khungu.
44. Mulungu amasintha usiku
ndi usana (Pambuyo pa usiku,
umadza usana. Ndipo pambuyo pa
usana, umadza usiku). Ndithu,
m'zimenezo muli phunziro kwa
Anthu ozindikira (zinthu).
45. Ndipo Mulungu adalenga
ndi madzi nyama Iliyonse; (madzi
ndicho chiyambi cha Zolengedwa
zonse). Zina mwa izo Zimayendera
mimba zawo; ndipo zina Mwa izo
zimayenda ndi miyendo iwiri;
Ndipo zina mwaizo zimayenda ndi
inayi. Ndithu Mulungu amalenga
chimene Wafuna; ndithu, Mulungu
ali ndi Mphamvu pachilichonse.
46. Ndithu, tavumbulutsa Aya
zofotokoza Momveka (chilichonse
chofunika pa Chipembedzo).
4a*
y
t&ty&ftK3$to<&
®j
9 * 9 9'J\ { Sh \«'£ ^&\'K*<A
Surat 24. An-Nur Juzu 18
751
^A *->!
Y t j>J» *jj~>
Ndipo Mulungu Amamuongolera
kunjira yolunjika amene Wamfuna.
47. Ndipo akunena (kuti):
"Takhulupirira Mulungu Ndi
Mtumiki, ndipo tamvera." Kenako
ena a iwo amatembenuka Pambuyo
pazimenezo; Ndipo iwo wo sali
okhulupirira.
48. Ndipo akawaitanira kwa
Mulungu ndi Mtumiki wake kuti
awaweruze pakati pawo, Ena a iwo
akukana zimenezo
(Akadzizindikira okha kuti
ngolakwa)
49. Koma akaona kuti
chilungamo chili kwa iwo? Iwo,
amam'dzera (Mtumiki
mwachangu) Uku akusonyeza
kumvera.
50. Kodi ali ndi matenda
m'mitima mwawo? Kapena
akukaika, kapena akuopa kuti
Mulungu ndi Mtumiki Wake
awachitira Chinyengo? Koma iwo
ndi amene ali Osalungama.
51. Ndithu yankho la Asilamu
akaitanidwa kwa Mulungu ndi
Mtumiki Wake kuti aweruze pakati
pawo Silikhala lina koma kunena
Kuti: "Tamva ndipo titsatira."
Iwowo ndiwo Opambana.
52. Ndipo amene amvera
Mulungu ndi Mtumiki Wake,
ndikumalemekeza Mulungu ndi
k 9'< 9 * ?99* &9 { V<"'l.
^'^m.m&&
iH »< »9'9* ,&9'\.\ 99"
Surat 24. An-Nur Juzu 18
752
^A *j*-1
V t j_jJl 5jj-»>
kumuopa, Iwowo ndiwo
opambana.
53. Ndipo akulumbirira dzina la
Mulungu, kulumbira Kwakukulu
kuti ukawalamula (kupita
Kunkhondo), ndithu apita. Nena:
"Musalumbire; kumvera kwanu
nkodziwika (Kuti nkwabodza);
ndithu, Mulungu Akudziwa nkhani
zonse zomwe muchita.
54. Nena: "Mverani Mulungu,
ndiponso Mverani Mtumiki. Koma
ngati mutembenuka, lye ali nazo
zimene wasenzetsedwa (kuti
Azifikitse kwa inu), (ndipo) inunso
muli nazo Zimene
m wasenzetsedwa (kuti muzitsate).
Ndipo mukamumvera, muongoka.
Ndipo Pa Mtumiki palibe china
chake koma Kufikitsa (uthenga)
moonekera.
55. Mulungu walonjeza mwa
inu amene Akhulupirira ndikuchita
ntchito yabwino kuti Ndithu
awathandiza kukhala oyang'anira
Padziko monga momwe
adawachitira amene Adalipo kale
kukhala oyang'anira; Ndipo
ndithu, awalimbikitsira
chipembedzo Chawo chimene
wawayanja nacho; ndipo
Awachotsera mantha awo kukhala
opanda Mantha". Akhale
akundirambira Ine,
Osandiphatikiza ndi chilichonse.
©
f?\' 9 &'te m.\f.
}"**>••*
at&
Surat 24. An-Nur Juzu 18
753
^A *jA-i
Y t j^Ji 3^
Ndipo Amene asiye kukhulupirira
pambuyo Pazimenezi, iwo
ngakuswa malamulo.
56. Choncho, pempherani swala
ndi kupereka "Zakaat;" ndiponso
mverani Mtumiki Kuti
mumveredwe chisoni.
57. Amene sadakhulupirire
musawaganizire Kuti
angamulepheretse Mulungu
padziko (kuwalanga) ndipo Malo
awo ndi kumoto. Ha! Kuipa Malo
obwererako!
58. E, inu amene
mwakhulupirira! Akuodireni
Amene manja ami akumanja apeza
ndi amene Mwa inu sanathe
msinkhu awodire nthawi zitatu:
Isanapempheredwe swala ya
m'mawa, Ndi pamene mukuvula
nsalu zanu nthawi Yamasana (kuti
mupumule), ndi pambuyo Pa swala
ya Isha (usiku). Izi ndi nthawi
Zitatu zomwe Inu mumakhala
wamba. Palibe Uchimo pa inu
ngakhale pa iwo pambuyo Pa
nthawi zimenezo (kulowa popanda
kuodira); Mumazungulirana pakati
Panu umo ndi momwe
Akukufotokodzerani Mulungu Aya
zake. Ndipo Mulungu Ngodziwa;
Ngwanzeru zakuya.
59. Ndipo mwainu ana akatha
msinkhu, aodire Monga momwe
adali kuodira omwe adalipo
\^&&1&W&
%ggfri'\»'4\
m?> ' ?\'& '&g "fry*. _ .» >?
®
A'vt '. >\
SO rat 24. An-Nur Juzu 18
754
^A frjA-i
1 1 jjJi ^j^
Patsogolo pawo. Umo ndi momwe
Mulungu Akukufotokozerani aya
Zake. Ndipo Mulungu Ngodziwa;
Ngwanzeru zakuya;
60. Nayonso mikwezembe
(nkhalamba Zachikhalire zazikazi)
Yomwe siyembekezera
kukwatiwa, Palibe uchimo paiyo
kusiya Kufunda nsalu zawo
(kumutu), popanda Kuonetsa
zodzikongoletsera zawo. Koma
ngati zikudzikakamiza kuleka
Kuvula mipangoyo, ndibwino kwa
iyo. Ndithu, Mulungu
Ngwakumva; Ngodziwa.
61. Palibe kulakwa pa akhungu
(osapenya) Ndiponso palibe
kulakwa pa olumala; Palibenso
kulakwa pa odwala, Ngakhalenso
pa inu eni ngati muli kudya
M'nyumba zanu kapena
m'nyumba za atate Anu, kapena
m'nyumba za amayi anu, Kapena
m'nyumba za abale anu, kapena
M'nyumba za alongo anu, kapena
M'nyumba za abambo anu
aang'ono kapena Aakulu, kapena
m'nyumba za azakhali anu,
Kapena m'nyumba za atsibweni
anu, kapena M'nyumba za amayi
anu aakulu kapena Aang'ono,
kapena m'nyumba za omwe
Mukuwasungira makiyi, kapena
(m'nyumba Za) anzanu; palibe
kulakwa pa inu ngati Mukudyera
h "'3?*l * ' * * 9 ~ 9 <> 9 Yki " .
Siirat 24. An-Niir Juzu 18
755
1A *>i
Y £ j>Jl 5jj-<
limodzi kapena payekhapayekha.
Ndipo mukamalowa m'nyumba
Dziperekereni nokha salaamu.
(Lonjero ili) Ndi malonje ochokera
kwa Mulungu Amadalitso, abwino.
Umo ndi momwe Mulungu
akukulongosolerani aya Zake kuti
Muzindikire.
62. Ndithu, Asilamu oona
ndiamene Akhulupirira mwa
Mulungu ndi Mtumiki Wake;
ndipo akakhala naye pachinthu
Chokhudza onse, sachoka mpaka
Atampempha (Mtumiki) chilolezo.
Ndithu, amene akukupempha
chilolezo, Iwowo ndi amene
akukhulupirira Mulungu ndi
Mtumiki Wake. Choncho
akakupempha chilolezo Chifukwa
cha zinthu zawo zina, Muloleze
mwaiwo amene wamfuna (ngati
Utaona kuti chidandaulo chake
Nchoona), ndipo uwapemphere
Chikhululuko kwa Mulungu;
ndithu, Mulungu Ngokhululuka
kwabasi; Ngwachisoni
63. Kumuitana Mtumiki pakati
panu Musakuchite monga momwe
Mumaitanirana nokhanokha,
ndithu, Mulungu akudziwa amene
akuchoka Pamalo mozemba ndi
modzibisa mwa inu. Achenjere
amene akunyozera lamulo Lake
kuti mliri Ungawapeze, kapena
Kuwapeza chilango chowawa.
&&&*$&
Surat 24. An-Nur Juzu 18 I 756 I \ A *j*-i
T i jjJl ^jj-**
64. Mverani! Ndithu, zili
kumwamba ndi Pansi nzake
Mulungu ndipo akudziwa Zimene
muli nazo. Ndipo patsiku Limene
adzabwezedwe kwa lye,
Adzawaudza zimene adachita
ndipo Mulungu Ngodziwa
chilichonse.
Surat 25. Al-Furqan Juzu 18 757 1 A *>i to aiS^di 3jj~-
Surayi yayamba ndi kufotokoza zaulemerero wa Qur'an, ndi
kuphanuka kwa ufumu wa Yemwe adaivumbulutsa; Yemwe
ufumu wakumwamba ndi pansi Ngwake.
Koma ngakhale ufumu Wake uli waukulu chonchi,
Amshirikina akumphatikiza ndi milungu ina pomwe lye ndi
mmodzi ndipo palibe wachiwiri wake, iwo akutsutsa Qur'an
pamodzi ndi uthenga wa Mtumiki Muhammad (madalitso ndi
mtendere zikhale naye) pomunena kuti angakhale Mthenga wa
Mulungu bwanji pomwe ali munthu; amadya chakudya
ndikumapita kumisika monga anthu ena. ndipo Amshirikina
akufuna kuti Mthengayo koma akadakhala mmodzi wa angelo.
Ndipo akuyankhidwa kuti Mulungu akadatuma mngelo monga
Mtumiki, ndiye kuti mngeloyo akadamsandutsa maonekedwe
ndi chikhalidwe chake kukhala monga anthu kuti amvane bwino
ndi anthu wo.
Amshirikina adatsutsa kuti kodi bwanji Qur'an
idavumbulutsidwa pang'onopang'ono, osati mwa nthawi imodzi
monga momwe zidalili ndi mabuku ena? Ndipo adawayankha
kuti zidachitika zimenezi ndi cholinga chanzeru zakuya.
Qur'an idapitiriza kuwafotokozera zomwe zidachitikira
Aneneri akale ndi anthu awo kuti likhale phunziro kwa iwo.
Koma Amshirikina sadacheukire zimenezi, adangotsatira
zilakolako zawo basi. Potero, adasokera ngati nyama kapenanso
kuposa nyama.
Tsono surayi yasonyeza zisonyezo zachilengedwe zomwe
zikuonetsa mphamvu za Mulungu. Ndipo surayi yamaliza ndi
kufotokoza mbiri za okhulupirira zomwe zikaalowetse anthuwo
ku Janna, m'minda ya mtendere momwe azikalandira malonje
abwino.
Surat 25. Al-Furqan Juzu 18 758 >A tji-i
T o JlSyJl 5 jj-o
Surat Al-Furqan XXV
_j^
mmZ
M'dzina la Mulungu waChifundo
Chambiri, waChisoni.
1. Watukuka Mwini kupereka
madalitso, Yemwe Wavumbulutsa
Qur'an kwa kapolo Wake kuti
Ikhale mchenjezi kwa zolengedwa
zonse.
2. (Mulungu) Yemwe Ngwake
ufumu Wakumwamba ndi
wapansi. Ndipo Sadabale mwana
ndipo alibenso Wothandizana naye
pa Ufumu (Wake). Adalenga
chinthu chilichonse ndikuchilinga
Mlingo Wake.
3. Ndipo m'malo mwa lye
(Mulungu weniweni,
Osakhulupirira) adzipangira
milungu yomwe Siilenga
chilichonse koma iyo ndiyomwe
Idalengedwa; ndiponso ilibe
mphamvu Yodzichotsera masautso
ngakhale Kudzidzetsera
zothandiza. Ndiponso Ilibe
mphamvu zoperekera imfa ndi
moyo, Ngakhale kuukitsa akufa.
4. Ndipo osakhulupirira
akunena: "Ichi sikanthu (Qur'an
imene Muhammad {SAW}wadza
Nayo) koma ndi chonama chimene
Wachipeka, ndipo pachimenechi
amthandiza Anthu ena (eni
o^J)f<^j)l^
Surat 25. Al-Furqan Juzu 18
759
^A *j*-i
Y o d\3jti\ 3jj--
mabuku)". Kunena zoona, I wo
(osakhulupirira) adza ndi
Chinyengo ndi bodza (pazonena
zawozi). ]
5. Ndipo (osakhulupirira)
akunena: "Iyi (Qur'an) Ndi nthano
za anthu akale zomwe
(Muhammad {SAW})
adazilembetsa. Choncho
Zikulakatulidwa kwa iye m'mawa
ndi Madzulo (kuti aloweze)",
6. Nena: "Adaivumbulutsa
Yemwe akudziwa Zobisika
zam'thambo ndi m'hthaka. Ndithu,
Iye ali Wokhululuka; Wachisoni,
(Nchifukwa chake sakukulangani
mwachangu Pazimene
mukunenazi)."
7. Ndipo akunena: "Ndi
Mtumiki wanji uyu, Womadya
chakudya Nkumayenda m'misika?
Kodi b wanji sadatumizidwe
Mngelo kwa iye kuti azikhala
Naye limodzi uku akuchenjeza?" 2
Osakhulupirira amumzinda wa Makka adali kuinyoza Qur'an namati ndi
Buku labodza limene walipeka yekhayekha Muhammad (SAW)
ndikumamnamizira Mulungu kuti ndiye walivumbulutsa. Amatinso anthu a
mabuku ndiwo adamthandiza kulipeka. Zonena zawozi nzabodza zokhazokha
chifukwa Qur'an yomwe Muhammad akuiwerengayo ili m'charabu osati
m'chiyuda.
2 Amamunenera zachipongwe Mtumiki Muhammad (SAW) kuti: "Nchiyani
watiposa uyu pamene akudzitcha yekha kuti ndi Mtumiki? lye akudya
chakudya monga momwe ife tidyera, ndipo akuyendayenda m'misika kunka
nafunafuna zokhalira moyo monga anthu ena onse achitira. Akadakhaladi
Mtumiki ndiye kuti Mulungu akadampatsa zosowa zake zonse. Ngati alidi
Mtumiki bwanji Mulungu sadamtsitsire angelo kumwamba kuti azimthandiza?
Zikadatero apo tikadamkhulupirira."
Surat 25. Al-Furqan Juzu 18 I 760 I ^ A *j*-»
V o OlSyiJl 5j^-rf
8. "Kapena kuponyeredwa
nkhokwe (Zachuma), kapena
kukhala ndi Munda ndikumadya
m'menemo?" Ndipo Osalungama
akuti: "Ndithudi, Mukutsatira
munthu wolodzedwa".
9. Ona momwe akukuponyera
mafanizo (omwe Sali oyenerana
nawe, nthawi zina akuti Ndiwe
wolodzedwa wamisala, wabodza,
Wophunzitsidwa ndi anthu ena)
choncho Asokera, ndipo sangathe
kupeza njira (Yoongoka
yokunenera)
10. Watukuka Mwini kupereka
madalitso Ambiri, Yemwe
akafuna, akuchitira Zabwino
kuposa zimenezi, (adzakupatsa pa
Tsiku lachimaliziro) Minda
yamtendere Yomwe pansi pake
pakuyenda mitsinje; ndipo
Adzakupangira nyumba
zikuluzikulu Zachifumu.
11. Koma akutsutsa zanthawi ya
Kiyama. Ndipo Tawakonzera moto
woyaka (iwo) amene Akutsutsa
zanthawi ya Kiyama
(Yachimaliziro.)
12. (Motowo) ukadzawaona
(naonso nkuuona) Kuchokera
pamalo apatali, (iwo) adzamva
Mkwiyo wamotowo ndi mkokomo
wake.
ti^tp wj, 6j^^' (j^%
<Sfoya»
Surat 25. Al-Furqan Juzu 18
761
)A *>»
Y o Ot$yJ» ijj~>
13. Ndipo akadzaponyedwa
m'menemo, pamalo Opanika uku
manja atanjatidwa Chakukhosi,
pamenepo adzaitana imfa (Kuti
iwafike, afe apumule
Kumasautsowo).
14. (Tidzawauza): "Lero
musaitane imfa Imodzi, koma
itanani imfa zambiri (Ndipo
simupeza mpumulo koma
mazunzo okhaokha)".
15. Nena: (kwa osakhulupirira)
"Kodi izi ndizo Zabwino, kapena
munda wamuyaya umene
Alonjezedwa oopa Mulungu kuti
udzakhale Mphoto (yabwino) kwa
iwo ndi kobwerera (Kotamandika)?
16. "M'menemo adzapeza
chilichonse chomwe Adzafune.
Adzakhala m'menemo
Muyaya.Mtenderewu ndi lonjezo
lochokera Kwa Mbuye wako pa
iwo lomwe Adampempha kuti
adzawakwaniritsire".
17. Ndipo (kumbuka) tsiku
limene Adzawasonkhanitse (awa
osakhulupirira) ndi Omwe adali
kuwapembedza (monga Yesu,
Uzairi ndi angelo) kusiya
Mulungu; adzanena (Mulungu
kuuza amene ankalambiridwawo):
"Kodi ndinu mudasokeretsa anthu
angawa, Kapena ndi okha
adasokera njira"
#ltZ\*. "L
Surat 25. Al-Furqan Juzu 19
762
^ tjA-i
T O d\3jti\ djj**>
18. Adzanena: "O, ulemelero
ukhale kwa Inu! Sizidali zoyenera
kwa ife kudzikonzera Atetezi
mmalo mwa Inu, (nanji kuuza
anthu Kuti azitipembedza). Koma
mudawasangalatsa Iwo ndi makolo
awo kufikira adaiwala Malangizo
(Anu). Ndipo adali anthu
Oonongeka."
19. (Mulungu adzati): "Ndithu,
yakutsutsani (Milungu yanuyo)
pazimene mwanena (Kuti iwo
adakusokeretsani). Ndipo simutha
Kudzichotsera (chilango) ngakhale
(kupeza) Chithandizo." Ndipo,
ndithudi, amene achite Zoipa mwa
inu, tidzamulawitsa chilango
Chachikulu.
20. Ndipo palibe pamene
tidatuma atumiki Patsogolo pako
koma ndithu iwo, adali kudya
Chakudya; ankayendanso
m'misika. Ndipo Tawasankha ena
mwa inu kuti akhale mayeso Kwa
ena (popereka masautso kwa
olungama). Kodi mupirira? Ndipo,
Mbuye wako ali Wopenya
(chilichonse).
21. Ndipo amene alibe
chiyembekezo Chakukumana nafe
akunena: "Bwanji angelo
Satumidwa kwa ife? Kapena
timuone Mbuye Wathu (kuti
atitsimikizire kuti ndiwedi
Mtumiki Wake"? Ndipo Mulungu
©IjS ^3
4'
*\ £» 9 "H\* 9< <\<*\Z *'"9)9\ £*Z
C \#9 *
Surat 25. Al-Furqan Juzu 19 763 H tjA-t YaOiSyliSj^
akunena): "Ndithu, adzitukumula
mmitima mwawo Ndipo anyoza;
kunyoza kwakukulu."
22. Tsiku lowaona Angelo,
sikudzakhala Chisangalalo tsiku
limenelo kwa Ochimwa, (koma
lidzakhala tsiku Lochoka moyo
wawo). Ndipo adzanena (tsiku
Limenelo): " Ha! Mulungu
Atitchinjirize" (koma mawu awa,
Sadzathandiza chilichonse).
23. Ndipo tidzaidzera ntchito
Iliyonse (yabwino) imene adachita,
ndipo Tidzaichita monga fumbi
louluka (Ponseponse, yopanda
phindu chifukwa cha
Kusakhulupirira Mulungu kwawo.)
24. Anthu akumunda
wamtendere tsiku limenelo
Adzakhala ndi mokhala
mwabwino, ndi Pamalo
pampumulo wabwino.
25. Ndipo akumbutse zatsikulo
pomwe thambo Lidzang'ambika
ndikudzetsa mitambo ( Yomwe
idzachititsa chimdima ponseponse)
Ndipo angelo adzatsika
ambirimbiri.
26. Tsiku limenelo ufumu
wachoonadi ngwa(Mulungu)
Wachifundo chambiri. Ndipo
Lidzakhala tsiku lovuta kwa
osakhulupirira.
Surat 25. Al-Furqan Juzu 19
764
M *&\
T o OlSyJl 3jj-*»
27. Ndipo tsiku (limenelo),
Wosalungama Adzakukuta zala
zake uku akunena: "Kalanga Ine!
Ndikadatsata njira ya Mtumiki."
28. "E, tsoka langa!
Ndikadapanda kumchita Uje
kukhala bwenzi wanga
(nkadapulumuka Lero)"
29. "Ndithu, adandisokeza
kufikira ndidasiya Ulaliki (Wa
Mulungu) utandidzera. Zoonadi,
Satana amataya munthu (akaona
kuti Wamgwetsa
m ' chionongeko) . ' '
30. Ndipo Mtumiki (adasuma
kwa Mbuye wake) Adati: "E,
Mbuye wanga! Ndithu, anthu
Anga aisandutsa Qur'aniyi kukhala
chinthu Chosiidwa, (sakuiwerenga.
Ndiponso Sakutsata ziphunzitso
zake)."
31. Momwemonso Mneneri
Aliyense tidamkonzera mdani
wochokera Mwa (anthu)
oipa.Ndipo Mbuye wako
Wakwana kukhala muongoli ndi
Mthandizi (wako).
32. Ndipo amene
sadakhulupirire akunena: "Bwanji
Qur'an yonse siidavumbulutsidwe
Nthawi imodzi kwa iye?
Momwemo (Ukuoneramo,
tikuitumiza Pang'onopang'ono)
kuti tiulimbikitse mtimaWako ndi
Surat 25. Al-Furqan Juzu 19 765 I > n *>»
V o OliyaJl 5jj--
iyo, ndipo taiyala,Mkayalidwe
kabwino.
33. Ndipo sangakubweretsere
fanizo lililonse Koma
tikubweretsera choonadi
(Choyankha fanizolo ndi
kukudziwitsa) ndi Ku masulira
kwabwino.
34. Amene adzasonkhanitsidwe
Akukokedwa ndi nkhope zawo
kunka ku Jahanama,iwowo
Adzakhala pamalo oipa Ndipo
ngosokera njira (yachoonadi).
35. Ndipo ndithu, Musa
Tidampatsa Buku. Ndipo M'bale
wake Haaruna (Aroni)
tidamsankha Kukhala nduna (yake).
36. Ndipo tidati: "Pitani Kwa
anthu omwe atsutsa Zisonyezo zathu.
Choncho, Tidawaononga kotheratu."
37. Naonso anthu a Nuhi,
Pamene adatsutsa Atumiki,
Tidawamiza, ndipo tidawachita
Kukhala phunziro kwa anthu,
ndipo anthu, Osalungama
tawakonzera chilango Chowawa;
38. Nawonso Adi, Asamudu ndi
eni chitsime Ndi mibadwo
yambiri Pakati pa iwo.
39. Ndipo onse tidawaponyera
mafanizo; ndiponso Onse
tidawaononga motheratu (pamene
Adakana kutsatira malamulo athu).
$taMk&£$S&'
©j££
Siirat 25. Al-Furqan Juzu 19 I 766 I > 1 *>' t ° atfyil* 5 J>*
40. Ndipo ndithu, iwo
(Akuraishi, m'maulendo awo)
Adafika pamudzi womwe mvula
yoipa Idawavumbwa. Kodi sadali
kuuona? Koma sadali
kuyembekezera Zakuuka ku imfa.
41. Ndipo akakuona (iwe
Mtumiki Muhammad {SAW}),
amangokuchitira chipongwe:
"Kodi uyu ndi yemwe Mulungu
wamtuma kuti Akhale mtumiki?"
42. "Ndithu, adatsala pang'ono
kutisokeretsa Kumilungu yathu,
tikadapanda kupirira
Pamilunguyo" Posachedwapa
Adziwa, pamene adzaona
Chilango, (kuti) ndani Wosokera
zedi njira.
43. Kodi wamuona yemwe
wachichita Chilakolako chake
(chimene akuchikonda) Kukhala
mulungu wake? Kodi iweyo
Ungathe kukhala muyang'aniri wa
iye (Kotero kuti ungamkakamize
chomwe Safuna)?
44. Kapena ukuganiza kuti
ambiri a iwo akumva Kapena
kuzindikira? Iwo sali kanthu Kena
koma ali ngati ziweto. Ndipo iwo
Asokera kwambiri njira.
45. Kodi sudaone momwe
Mbuye wako Wautambasulira
mthunzi? Akadafuna, Akadauchita
kuti ukhale wokhazikika
S9'*>'9 / 9 9<9' ' 9S*jrs& \'9' '
w**-
Surat 25. Al-Furqan Juzu 19
767
H *>i
Y o OtSjiJl 5jj-j
(Wosasinthasintha). Ndipo
talichita Dzuwa kukhala
chisonyezo chake; 1
46. Kenaka tikuufumbata kwa
Ife M'kufumbata
kwapang'onopang'ono (Kufikira
wonse wutachoka).
47. Ndipo lye ndi amene
wakuchitirani usiku Kukhala
monga chovala, ndipo tulo Monga
mpumulo, ndipo usana wauchita
Kukhala monga nthawi youka
(kuimfa).
48. lye ndi Yemwe amatumiza
mphepo Kukhala nkhani yabwino
Patsogolo pa chifundo Chake
(mvula), Ndipo kuchokera
kumitambo Tikutsitsa madzi oyera
49. Kuti ndi madziwo tiukitse
dziko lakufa (Lachilala),
ndikumwetsa Zina mwa zimene
tidazilenga Monga ziweto ndi
anthu Ochuluka.
50. Ndiponso ndithu, tikuigawa
(mvulayi) pakati Pawo kuti
akumbukire,ndipo anthu ambiri
Akukana (kuthokoza Mulungu)
koma Kupitiriza kusakhulupirira.
$&>&£
e^SS^^S
1 Apa Mulungu akuti kodi sukuona luso la Mulungu pa zopangapanga Zake
ndi mphamvu Zake zoposa momwe amautambasulira mthunzi nthawi
yamasana kuti munthu akhale pamthunzi ndikupeza mpumulo wabwino
kuchoka mkutentha kwa dzuwa. Pakadapanda mthunzi ndiye kuti munthu
akadatenthedwa ndi dzuwa ndikusowetsedwa mtendere pamoyo wake. Ndipo
Mulungu akadafuna akadauleka mthunzi kuti ukhale pamalo amodzi. Koma
lye ndi mphamvu Zake zoposa adaupanga kukhala wosinthasintha.
Surat 25. AI-Furqan Juzu 19 768 | ] * *>* 1° Otfjili t^
51. Ndipo tikadafuna,
tikadatuma mchenjezi
Wawowawo m'mudzi uliwonse,
(koma Tatuma Muhammad
{SAW}kutiakhale
Mchenjezi waonse).
52. Choncho usawamvere
osakhulupirira Koma limbana
nawo ndi iyo (Qur'an); kulimbana
kwakukulu.
53. Ndipo lye (Mulungu) ndi
Yemwe Wazikumanitsa nyanja
Ziwiri,iyi yamadzi Okoma othetsa
ludzu Ndi iyi yamadzi amchere
owawa. Ndipo waika malire ndi
Chitsekerezo chotsekereza pakati
pa izo.
54. Ndipo lye ndiye adalenga
munthu ndi madzi Ndiponso
adamchitira chibale cha magazi
Ndi chibale cha ukwati. Ndipo
Mbuye Wako ali Wokhoza
chilichonse.
55. Ndipo (ena mwa anthu)
akupembedza Zina zake kusiya
Mulungu, zomwe
Sizingawathandize ndiponso
Sizingawadzetsere masautso
(atasiya Kuzipembedza). Ndipo
wosakhulupirira ndi Mthandizi wa
zoipa poukira Mbuye wake.
56. Ndipo Ife sitidakutume
koma kuti ukhale Wouza nkhani
asftzRStWkss
*>><*'<
®©j]^$&$j
Surat 25. Al-Furqan Juzu 19
769
>^ ^j*-i
V O d\&jti\ djj--
zabwino (okhulupirira); ndi
Wochenjeza (osakhulupirira).
57. Nena: "Sindikupemphani
malipiro Pazimenezi (zomwe
ndikukuphunzitsani) Koma amene
afuna ayende panjira Yopita kwa
Mbuye wake, (Popanda
chopereka)."
58. Ndipo tsamira kwa
(Mulungu) Wamoyo,Wamuyaya
Yemwe saafa. Ndipo Mulemekeze
pomtamanda ndi mbiri Zake.
Ndipo lye akukwana kudziwa
Bwinobwino machimo a akapolo
Ake;
59. Yemwe adalenga thambo
ndi nthaka ndi Zimene zikupezeka
mkati mwake. (Adazilenga)
m'masiku asanu ndi limodzi,
Ndipo adakhazikika pampando
Wake Wachifumu (mkukhazikika
kodziwa yekha). lye
Ngwachifundo chambiri;
mufunseni Wodziwa za lye.
60. Ndipo akauzidwa (kuti):
"Mulambireni (Mulungu)
Wachifundo chambiri." Amati:
"Ndani Wachifundo chambiri?
Kodi Tilambire Yemwe iwe
ukutilamula?" (Mawu Amenewa)
adawaonjezera iwo mwano.
61. Watukuka Mwini kupereka
madalitso Yemwe adakhazikitsa
nyenyezi kuthambo, Ndipo
j*$&
Surat 25. AI-Furqan Juzu 19 770 \ * *j*-» Y otSytfi oj^»
m'menemo adaika nyali (dzuwa)
Ndi mwezi wounika;
62. Ndipo lye ndi Yemwe
adapanga usiku Ndi usana kuti
zizitsatana (Ndikusinthana). (Izi
zingapindulitse) kwa Amene afuna
kukumbukira kapena (amene)
Afuna kuthokoza.
63. Ndipo akapolo a (Mulungu)
Wachifundo Chambiri ndi omwe
akuyenda padziko Modzichepetsa,
ndipo Mbuli zikanena kwa iwo
(Mawu amwano), amaziyankha
Mawu abwino.
64. Ndi omwe amapititsa
nthawi inaYausiku uku akulambira
ndi kuimirira Chifukwa
chakulemekeza Mbuye wawo;
65. Ndi omwe akunena, "E,
Mbuye Wathu tichotsereni
Chilango cha Jahannama; Ndithu,
chilango chake Nchosasiyana
nacho.
66. "Ndithu, iyo ndi malo
woipa; Ndiponso pokhala poipa."
67. Ndi omwe amati
akamagawira anthu ena Chuma
chawo, samwaza pachabe
ndiponso Sachita umbombo, koma
amachita Mwapakatikati.
68. Ndi omwe sapembedza
milungu ina Poiphatikiza ndi
Mulungu, ndiponso Saapha
^%lli|ij(^i &&£&i$3
^fffeJSW^""'^
Surat 25. Al-Furqan Juzu 19
771
H *>i
To d\3jal\ Ojj-*>
munthu yemwe Mulungu adaletsa
Kumupha kupatula pakakhala
choonadi Ndiponso saachita
chigololo. Ndipo amene achite
zimenezi, apeza Masautso
(pompano padziko lapansi).
69. Chilango
chidzawonjezeredwa kwa iye
Tsiku la Kiyama, ndipo adzakhala
M'chilango muyaya uku ali
wonyozeka;
70. Kupatula amene walapa,
Naakhulupirira, ndikuchita ntchito
Yabwino. Tsono iwowo, Mulungu
Adzawasinthira zoipa zawo
kukhala Zabwino. Ndipo Mulungu
ali Wokhululuka Kwambiri,
Wachisoni,
71. Ndipo amene akulapa
ndikuchita zabwino, Ndithu, iye
akulapa mwachoonadi kwa
Mulungu.
72. Omwenso sachitira umboni
zabodza, Ndipo akadutsa pamalo
pazachibwana, Amadutsa
mwaulemu;
73. Ndiponso omwe amati
akakumbutsidwa Aya za Mbuye
wawo, samazigwera Mwaugonthi
ndi mwakhungu;
74. Ndi omwenso akunena: "E,
Mbuye wathu Tipatseni mwa akazi
athu ndi ana Athu chotonthoza
Qys%&&Jz%&h
&'
is*
^VJ&Pi
Surat 25. Al-Furqan Juzu 19 I 772 I \ * fjA-i Y d&jd\ oj^
maso, ndipo tichiteni Kukhala
atsogoleri A oopa Mulungu."
75. Iwo adzalipidwa nyota
Zapamwamba chifukwa Cha
mavuto omwe Adawapirira. Ndipo
Akalandira m'menemo Ulemu ndi
mtendere,
76. Akakhala m'menemo
muyaya; malo abwino Ndi
pokhala pabwino.
77. Nena, "Ndithu,Mbuye
wanga sakadalabadira Chilichonse
pa inu pakadapanda Mapemphero
anu, (akadakulangani pompano
Padziko lapansi.) Komabe inu
mwatsutsa (Uthenga wa aneneri).
Choncho chilango
Chidzakugweranibe."
@M2Uj\ ffi »*«£*..rS^^fl^>
Surat 26. Ash-Shu'ara Juzu 19
773
H *>»
V 1 *ly*JiJl Ojj--.
M'surayi muli izi:- Kumayambiriro kwake yafotokoza
zaulemelero wa Qur'an. Ndiponso yaopseza okanira onse kuti
Mulungu akhoza kuwatsitsira chilango pompano padziko
lapansi. Ndipo yamtonthoza Mtumiki (madalitso ndi mtendere
zikhale naye) pamasautso amene adakumana nawo kwa anthu
ake pomufotokozera zamasautso omwe atumiki anzake
adakumana nawonso kuchokera kwa anthu awo. Yafotokozanso
zakukumana kwa Musa, Haarruna ndi Farawo, ndikuti Farawo
adatsutsa uthenga wa awiriwa. Ndipo yafotokozanso nkhani ya
Ibrahim yemwe ndikholo la aneneri, ndi nkhani ya Nuhi
pamodzi ndi anthu ake; ndi nkhaninso ya Hudu pamodzi ndi
Adi, ndi nkhaninso ya Swaleh pamodzi ndi Asamudu.
Ndipo surayi yafotokoza mwatsatanetsatane za ulaliki wa
Luti ndi Shuaibu. Ndipo wolingalira aona m'nkhani za anenerizi
kuti maziko a ulaliki wawo ndi amodzi; ndikuti njira ya otsutsa
ndi imodzinso poukana uthenga wa aneneri wo.
Surayi yamaliza ndikunena za ulemerero wa Qur'an monga
momwe yafotokozera kumayambiriro kwake. Ndipo yanena,
komalizirako, kuti Qur'an sindakatulo.
Surat 26. Ash-Shu'ara Juzu 19 I 774 I \ * *>
T *\ *1yuiJl 3jj-*>
Surat Ash-Shu'ara XXVI
M'dzina la Mulungu waChifundo
Chambiri, waChisoni.
1. Td-Sin-Mtm.
2. Izi ndi aya za Buku (la
Qur'an) lofotokoza Chilichonse
(chofunika m'chipembedzo).
3. Mwina iwe (Mtumiki
Muhammad{SAW}) Udziononga
wekha (ndi madandaulo)
Chifukwa chakuti (iwo) sadakhale
Asilamu.
4. Tikadafuna, tikadawatsitsira
chizizwa Kuchokera kumwamba;
makosi awo Akadadzichepetsa ndi
chizizwacho,(sakadatha
Kucheukira kwina koma sitifuna
kukakamiza Anthu kuti akhale
Asilamu). 1
5. Ndipo palibe pamene
chikuwadzera Chivumbulutso
chatsopano chochokera kwa
(Mulungu) Wachifundo chambiri
koma Amazipatula ku icho
(chivumbulutso).
wm&'hm
oA^t^jlt^l,
©.
»j
1 Mtumiki Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale naye) adali
kuwawidwa mtima kwambiri poona kuti anthu sakuvomereza uthenga
wachoonadi umene iye adadza nawo, ndipo adali kuwamvera chisoni
kwambiri. Choncho Mulungu adamtonthoza pomuuza kuti "Usadziphe wekha
chifukwa chokhala ndi maganizo owamvera chisoni". Mulungu akadafuna
kuwaongola mowakakamiza akadatha kutero; koma sadafune.
Surat 26. Ash-Shu'ara Juzu 19
775
^ fr>1 t *\ t\jLXS\ OjJ-
6. Ndithu, atsutsa; choncho
posachedwapa Ziwadzera nkhani
zomwe adali kuzichitira
Chipongwe.
7. Kodi sadaone nthaka? Ndi
mmera ungatiTaumeretsa
m'menemo wamtundumtundu,
Wokongola?
8. Ndithu, m'zimenezo muli
zizindikiro (Zosonyeza mphamvu
za Mulungu). Koma Ambiri a iwo
sali okhulupirira.
9. Ndipo, ndithu, Mbuye wako
ndi mwini Mphamvu zoposa;
Wachisoni.
10. Ndipo (akumbutse) Pamene
Mbuye wako adaitana (m'neneri)
Musa; adamuuza:"Pita kwa anthu
ochita zoipa,
11. Anthu a Farawo; (auze):
Kodi sawopa (Mulungu)?"
12. (Musa) adati: "Mbuye
wanga! Ine ndikuopa Kuti
anganditsutse;
13. Ndipo chingabanike
chifuwa changa (ndi Maganizo,
chifukwa chakunditsutsa kwawo);
Ndiponso lirime langa siliyankhula
Momveka bwino. Choncho
tumizaninso Uthengawu kwa
Haaruna (kuti tikhale awiri Ndipo
azikandithangata pantchito
yangayi).
^%e^jSi«K^
^&&s&m&
CHJ&&*
ty*38$&a$>&
Surat 26. Ash-Shu'ara Juzu 19
776
\ * frjJrl Y ^ *\jl*}\ djj^
14. Ndipo iwowo ndili nawo
mlandu Ndipo ndikuopa kuti
angandiphe (Pobwezera chimene
ndidawalakwira Powaphera
munthu wawo).
15. (Mulungu) adati: Iyayi!
Pitani Pamodzi ndi zozizwa Zathu;
ndithu, Ife Tikakhala nanu limodzi
(pokuthangatani) Uku
tikumvetsera (zimene azikanena).
16. Choncho mpitireni Farawo,
ndipo Kamuuzeni kuti: "Ife ndi
atumiki Ambuye wa zolengedwa
zonse;"
17. (Tatumidwa) kuti
uwapereke kwa ife Ana a Isiraeli
(kuti tinke nawo ku Shamu)."
18. (Farawo) adati (kwa Musa):
"Kodi Sitidakulere kwathu uli
mwana, ndi kukhala Nafe pamoyo
wako zaka zambiri?
19. Ndipo udachita chochita
chako chimene Udachichita, ndipo
iwe ndiwe mmodzi wa Osathokoza!"
20. (Musa) adati: "Ndidachita
zimenezo Pomwe ine ndidali
mmodzi wa osazindikira Zinthu.
21. Choncho ndidakuthawani
pomwe Ndidakuopani; tsono
Mbuye wanga Wandipatsa nzeru
zoweruzira (zinthu), ndi
Kundisankha kukhala mmodzi wa
atumiki.
1 $$%3&&2&ffi&
^zm$&M
ftSBgs^aa
mj^j^^^m^
W5
y S9 '\ 9 9
&^£&$@S*££&
Surat 26. Ash-Shu'ara Juzu 19
777 1 ^ *j*-l T 1 ttyutJl 3jj--
22. Ndipo kodi umenewu
ndimtendere Wonditonzera pomwe
mudawaika muukapolo Ana a
Israeli!"
23. Farawo adati: "Kodi ndani
Mbuye Wazolengedwayo?"
24. (Musa) adati: "Mbuye wa
thambo ndi nthaka Ndi zapakati
pake, ngati muli ndi
Chitsimikizo . ( Amachita
chilichonse M'menemo mmene
wafunira; kupereka Moyo ndi
imfa)."
25. (Farawo) adauza omwe
adali m'mphepete Mwake
(mwachipongwe): "Kodi
simukumva (Mawu
achibwanawa)?"
26. (Musa adapitiriza kunena)
adati: "Mulungu Ndi Mbuye Wanu
komanso Mbuye wamakolo Anu
oyamba".
27. (Farawo) adati (kwa anthu
ake pofuna Kuwakwiitsa):
"Ndithu, Mtumiki Wanu amene
watumidwa kwa inu, Ngwamisala".
28. (Musa) adati "Mbuye
wakuvuma ndi Kuzambwe, ndi
zomwe ziri pakati pake Ngati
mumazindikira (zinthu,
Muzindikira izi)".
29. (Farawo) adati: "Ngati
udzipangira mulungu Wina kusiya
8&^5^ftM&
%^m^^^
®ri&&>\
vtm\>x$&z%yjs
98®&$W&&t$$S
Surat 26. Ash-Shu'ara Juzu 19
778 H *j*-»
Y *\ *tyuiJl 3jj--
ine, ndikuchita Kukhala mmodzi
wa omangidwa kundende."
30. (Musa) adati: "Kodi
ngakhale Nditakubweretsera
chinthu choonekera Poyera
(chosonyeza kuti zimene
ndikunenazi Ndizoona
ndatumidwa ndi Mulungu)?
31. (Farawo) adati
"Chibweretse, ngati uli Mwa
onena zoona."
32. Ndipo (Musa) adaponya
(pansi) ndodo Yake, mwadzidzidzi
idasanduka njoka Yopenyeka.
33. Ndipo adautulutsa mkono
wake; pompo Udali woyera
(kwambiri) kwa (onse) Openya.
34. (Farawo) adauza akuluakulu
omwe adali M'mphepete mwake:
"Ndithu, uyu ndi Wamatsenga
wodziwa kwambiri;
35. Akufuna kukutulutsani
m'dziko lanu ndi Matsenga ake;
kodi Nanga mukuti chiyani?" 1
36. (Anthu) adati (kwa Farawo):
"Mpatse nthawi Ndi mbale
wakeyo, ndipo tumiza (amithenga)
M'mizinda yonse osonkhanitsa
anthu.
1 Farawo adasimidwa, adatha nzeru zedi ndi mawu amene adali kutuluka
m'kamwa mwa Musa kotero kuti adangoti kakasi, kusowa chonena, nayamba
kuwafunsa nzeru ndi malangizo anthu ake pomwe iye ankadzitcha kuti
ndimulungu wodziwa zonse, wamphamvu zoposa.
Surat 26. Ash-Shu'ara Juzu 19
779
y ^ frj^ri r n t iy^J» o^^
37. Ndipo akubweretsera
amatsenga onse Odziwa kwabasi
(kotero kuti adzampambana
Musa)"
38. Choncho amatsenga
adasonkhanitsidwa M'nthawi ya
tsiku lodziwika,
39. Ndipo anthu adaudzidwa:
"Kodi inu Musonkhana? (choncho,
sonkhanani).
40. Mwina tingawatsatire
Amatsenga ngati iwo Ndiamene
apambane."
41. Ndipo pamene amatsenga
Adadza,adati kwa Farawo: "Kodi
tidzakhala ndi mphoto Ngati ife
ndife tipambane?"
42. (Farawo) adati: "Inde,
(ndipo kuonjezera apo) Ndithu inu
mudzakhala mwa amene
Amakhala pafupi (ndi ine, monga
nduna Zanga)".
43. Musa adati kwa iwo:
"Ponyani zimene Mufuna kuponya
(zosonyeza kuya kwa Matsenga
ami)."
44. Choncho adaponya zingwe
zawo ndi ndodo Zawo, ndipo adati:
"Kupyolera m'mphamvu Za
Farawo, ndithu, ife ndife opambana."
45. Kenako Musa adaponya
yake; Mwadzidzidzi iyo idameza
zabodza Zomwe iwo adakonza.
®*W*:#3$r
k$2&&$?&r&
*%^%&M£&
etgB&foSStif&XCfi
as&W
Sfirat 26. Ash-Shu'ara Juzu 19
780
1 ^ *j*-» Y *\ tljuJJl 0^^
46. Pamenepo amatsenga
adazigwetsa pansi Molambira,
47. Adati: "Tamkhulupirira
Mbuye Wazolengedwa,
48. Mbuye wa Musa ndi
Haaruna."
49. (Farawo) adati: "Ha!
Mwamkhulupirira Chotani
ndisanakulolezeni? Ndithu, Iyeyu
ndimkulu wanu amene
Adakuphunzitsani matsenga.
Choncho Posachedwa mudziwa
(Chimene ndikuchiteni)ndithu
ndidula manja anu ndi miyendo
yanu Mosinthanitsa (podula
mkono wakumanja Ndi mwendo
wakumanzere; kapena Kudula
mkono wakumanzere ndi mwendo
Wakumanja), ndipo kenako
Ndikupachikani nonsenu."
50. (Amatsenga) adati: "Palibe
vuto, ndithu, Ife (tonse) tibwerera
Kwa Mbuye wathu"
51. Ndithu, ife tikuyembekezera
kuti Mbuye wathu atikhululukire
zolakwa Zathu; pokhala oyamba
Mwa okhulupirira".
52. Ndipo tidamvumbulutsira
Musa (kuti): "Pita ndi anthu anga
m'nthawi yausiku (Musamuke
m'dziko la Iguputo); ndithu, Inu
mutsatidwa."
53. Choncho Farawo adatuma
(owatuma) Kuti asonkhanitse
«Qs»
&t'*£L.&C&\?.Z:;
V&9-y#0^\&{&tti
Surat 26. Ash-Shu'ara Juzu 19
781
> H frj^rl 1 1 frlycJJt 5jj--
anthu m'mizinda (Kuti aletse
Ayuda kutuluka).
54. (Adawauza otumidwa aja
kuti auze Anthu kuti): "Ndithu,
awa (Ayuda) Ndikagulu kochepa,
55. Ndipo iwo akutikwiitsa;
56. Koma ife tonse(ndife
ochuluka komabe Ngakhale zili
choncho) tikuwaopa."
57. Choncho tidawatulutsa
m'minda ndi Mwa akasupe,
58. Ndi m'nkhokwe zachuma
ndi m'malo Okongola;
59. Momwemo ndi mmene
tidawachitira Ndipo
tidawalowetsera chokolo Zinthu
zawo zonse kwa ana a Israeli.
60. Choncho (anthu a Farawo
ndi iye mwini) Adawatsatira
(Ayuda) dzuwa Litatuluka.
61. Ndipo pamene magulu awiri
adaonana (Anthu a Farawo ndi
Ayuda), anthu a Musa adati:
"Ndithu, ife Tigwidwa."
62. (Musa) adati: "Iyayi! Ndithu
Mbuye wanga ali nane
pamodzi.Andiongolera (kuti ife
tonse Tipulumuke)."
63. Ndipo tidam'vumbulutsira
mawu Musa (Akuti):"Menya
nyanja ndi ndodo Yako." Ndipo
%$£*$&&
^'^fatf!'*
<fe 9P<* \ ' 9 * 9*\9*9$f
/^iSu^I^^\(j^(J3tj*-jSa
Surat 26. Ash-Shu ara Juzu 19
782
>* tjk-\ y i t\jL±)\ oj^
idagawikana, mbali Iliyonse idali
ngati phiri lalikulu.
64. Ndipo tidawayandikitsa
pamenepo Anthu enawo, (Farawo
ndi anthu ake Nalowa panjira
yomweyo pambuyo pa Musa Ndi
anthu ake).
65. Ndipo tidapulumutsa Musa
ndi onse Amene adali nawo
(mpaka adaolokaNyanjayo, madzi
ali chiimire Mbali iyi ndi iyi).
66. Kenako tidawamiza enawo,
(Farawo Ndi anthu ake).
67. Ndithu, pazimenezi pali
lingaliro. Koma ambiri aiwo sali
okhulupirira.
68. Ndipo, ndithu Mbuye wako
ndimwini Mphamvu zoposa
(amalanga ndi Chilango choopsa
omwe amunyoza); Wachisoni
(kwa omkhulupirira Ndi
kumumvera).
69. Ndipo awerengere
(osakhulupirira) Nkhani ya
(M'neneri) Ibrahim,
70. Pamene adafunsa bambo
wake ndi anthu Ake (kuti): "Kodi
mukupembedza Chiyani?"
71. Adati: "Tikupembedza
mafano; Ndipo tipitiriza
kuwapembedza."
72. (Ibrahim) adati: "Kodi
amakumvani Mukawaitana
®t*ms%i
Surat 26. Ash-Shu'ara Juzu 19 I 783 I > * *j*-» t n ^iyuiJi Sj^
73. kapena amakuthandizani
(Mukawapembedza) kapena
amapereka Masautso kwa inu
(mukasiya kuwapembedza)?
74. (Iwo) adati: "Koma tidapeza
makolo athu Akuchita zimenezi."
75. (Ibrahim) adati: "Kodi
mukuona awa Amene mwakhala
mukuwapembedza,
76. Inu ndi makolo anu amene
adatsogola?
77. Ndithu, iwo ndiadani anga,
Kupatula Mbuye wa zolengedwa
zonse;
78. Yemwe adandilenga,
ndiponso Yemwe Akundiongolera
(kunjira yolungama);
79. Ndiyemwe akundidyetsa ndi
Kundimwetsa.
80. Ndipo ndikadwala
ndiyemwe Amandichiritsa.
81. Ndi Amene adzandipatsa
imfa, ndipo (Tsiku la Kiyama)
adzandidzutsa;
82. Ndi Yemwe
ndikuyembekezera kuti
Adzandikhululukira zolakwa zanga
Tsiku la malipiro.
83. E, Mbuye wanga!
Ndipatseni nzeru Zoweruzira
(zinthu), ndikundilumikiza Ndi
anthu abwino;
%SXZ
^mo0^'^^
Surat 26. Ash-Shu'ara Juzu 19
784
> * ftjA-» x l t\jcxl\ ojf
84. Ndipatseni kutchulidwa
Kwabwino kwa anthu ena Odza
pambuyo;
85. Ndichiteni kukhala mmodzi
Mwa olandira munda wamtendere;
86. Ndipo khulukirani bambo
wanga; Ndithu, iye adali mmodzi
wa osokera;
87. Ndipo musadzandiyalutse
patsiku Loukitsidwa anthu (ku
imfa);
88. Tsiku lomwe chuma ndi ana
Sizidzathandiza (aliyense)
89. Kupatula yemwe adzadza
kwa Mulungu Ndi mtima woyera
(iye ndiamene Adzathandizidwa
patsikulo);"
90. Ndipo munda wamtendere
Udzayandikitsidwa kwa oopa
(Mulungu),
91. Ndipo Jahannama
idzaonetsedwa kwa opotoka;
92. Ndipo kudzanenedwa kwa
iwo: "Ali kuti amene mudali
kuwapembedza aja,
93. M'malo mwa Mulungu?
Kodi angathe Kukuthandizani
kapena Kudzithandiza okha?"
94. Ndipo iwo ndi opotoka ena
adzaponyedwa Ndi nkhope zawo
M'menemo (mu Jahannama).
"^.t
' 9<j^Au,5*?"^
^wwass&a&i;
Gi&^&j^
W"XX ^Ul,'^ '&!&i / *\l': 1 1
**Wff$$.
®j&<J&M&%
®0^&\<Ml
®,
%$&%<&.
*%
® (^liJ^S^l^W'^^ls
X< *>>>.' Y± i\ >* »
%&\#^&
Siirat 26. Ash-Shu'ara Juzu 19 785 ^ * *j*-i X 1 ^y^\ oj^
95. Ndi magulu onse ankhondo
a Iblis (Omwe adali kukometsa
kwa anthu Zoipa ndi machimo).
96. Adzanena (movomereza
kulakwa kwawo) Uku naonso ali
m'menemo, akukangana (Ndi
anzawo omwe adawasokeretsa):
97. "Ndikulumbira Mulungu,
ndithu, Tidali m'kusokera
kowonekera.
98. Pamene timakufananitsani
Ndi Mbuye wazolengedwa.
99. Ndipo sadatisokeretse
(onse) Koma oipa okha basi.
100. Choncho ife tilibe aomboli
(Otiombola),
101. Ngakhalenso bwenzi
wapamtima (Woti angatipulumutse
kumasautsowa).
102. Tikadapeza mwayi
wobwerera (kumoyo Wapadziko),
tikadakhala Mwa okhulupirira."
103. Ndithu, m'zimenezi, muli
malingaliro Aakulu, koma ambiri
Aiwo sali okhulupirira.
104. Ndipo ndithu, mbuye
wako, ndiye Mwini mphamvu
zoposa; Wachisoni.
105. Anthu a Nuhi adatsutsa
atumiki.
106. Pamene adawauza Nuhi
m'bale Wawo kuti: "Kodi
<£y »-? <sr \"j jgiffi
v
®'i.-X>Arr~
®k
*&£<&&
®&^z&m®&
%mj>£*%&
<$3G$&&&m
Surat 26. Ash-Shu'ara Juzu 19
786
\ * *j*-» V \ i\jK±S\ 5jj--
simufuna kuopa (Mulungu
ngakhale nditakuuzani zoopsa
Zimene zikukudikirani)?
107. Ndithu, ine kwa inu ndine
Mtumiki Wokhulupirika;
108. Choncho muopeni
Mulungu ndipo Ndimvereni.
109. Ndipo sindikupemphani
malipiro pazimenezi; Malipiro
anga ali kwa (Mulungu) Mbuye
wazolengedwa.
110. Choncho muopeni
Mulungu ndipo Ndimvereni."
111. (I wo) adati: "Nchotani kuti
tikukhulupirire Iwe chikhalirecho
anthu wamba ndi Amene
akukutsatira?"
112. (Nuhi) adati:
"Sindikudziwa zimene Adali
kuchita (zomwe zachititsa kuti
Mulungu awaongolere kunjira
yoongoka).
113. Chiwerengero chawo
sichili kwina Koma kwa Mbuye
wanga, mukadakhala
Mukuzindikira.
114. Ndipo sindine wopirikitsa
okhulupirira (Ku chipembedzo cha
Mulungu kuti Inu olemekezeka
muchikhulupirire) .
115. Ine sikanthu , koma ndine
mchenjezi Woonekera."
M^mz&&]&&.j
vj
s^$&&ffc*a
'* ^«5i r^r-^P^
yjh$»\0
©^&s*6f<a
Surat 26. Ash-Shu'ara Juzu 19
787
M *>l V\ tljiuSJl 3jj~>
116. (Iwo) adati: "Ngati susiya,
iwe Nuhi, Zonena zakozi) ukhala
mmodzi mwa Ogendedwa (miyala
mpaka ufe)."
117. (Nuhi) adati (kwa
Mulungu): "Mbuye Wanga!
Ndithu anthu anga anditsutsa.
118. Choncho weruzani pakati
panga ndi Pakati pa iwo
(chiweruzo chabwino), Ndipo
ndipulumutseni pamodzi ndi
amene Alinane mwa okhulupirira."
119. Choncho, tidampulumutsa
pamodzi ndi Omwe adali naye
m'chombo chodzadza (Ndi
chilichonse chamoyo chomwe
Chidalipo m'dziko, chachimuna
ndi Chachikazi chidaikidwa
m'menemo).
120. Pambuyo pake tidawamiza
otsalawo.
121. Ndithu, m'zimenezi muli
malingaliro; Koma ambiri a iwo
Sadali okhulupirira.
122. Ndipo ndithu, Mbuye
wako, lye Ngwamphamvu zoposa;
Ngwachisoni
123. Naonso Adi adatsutsa
atumiki.
124. Pamene m'bale wawo
(Mneneri) Hud Adawafunsa kuti;
"Kodi simuopa Mulungu?
#^«#<&#ae
" £ 9 " 9 *<£&*< 9 )*9" 9 9S9+KK*
©(• ** '-
k^^&^s&^SR
Surat 26. Ash-Shu'ara Juzu 19
788
\ * ftj*-* r ^ tiyuJi d J>( -
125. Ndithu, ine ndine Mtumiki
wokhulupirika Kwa inu;
126. Choncho, muopeni
Mulungu ndipo Mverani ine.
127. Ndipo pazimenezi
sindikukupemphani Malipiro;
ndithu, malipiro anga ali Kwa
(Mulungu) Mbuye wazolengedwa.
128. Kodi mukudzimangira
nyumba pamalo Paliponse
pachitunda, pokongola
Moseweretsa?
129. Ndipo mukudzimangira
(nyumba zonga) Linga ngati kuti
mukuona kuti Mudzakhala muyaya?
130. Ndipo mukamamenya
Nkhondo mumamenya
Modzitukumula.
131. Choncho muopeni
Mulungu ndipo Ndimvereni.
132. Ndipo muopeni Yemwe
adakupatsani Zimene mukuzidziwa.
133. Adakupatsani ziweto ndi ana,
134. Ndi minda ndi akasupe.
135. Ndithu, ine
ndikukuoperani chilango Cha tsiku
lalikulu."
136.Adati:"Kwaife
nchimodzimodzi, Utichenjeze
kapena iwe usakhale Mmodzi mwa
ochenjeza.
i >&A"i/. v:f?\*\"\§
&&&\<&$%2
Siirat 26. Ash-Shu'ara Juzu 19
789
> ^ *>i r n i\j*^\ ojj-*
137. Ndithu, kutero (anthu ena
Kudzitcha atumiki a Mulungu),
sikanthu Koma ndi machitidwe a
anthu akale.
138. Ndipo ife sitidzalangidwa
(monga Mom we ukunenera)."
139. Choncho adamtsutsa,
ndipo Tidawaononga. Ndithu,
m'zimenezi muli Malingaliro;
koma ambiri aiwo sadali
Okhulupirira.
140. Ndipo ndithu, mbuye wako
ndiye Wamphamvu zoposa;
Wachisoni.
141. A Samudu (naonso)
adatsutsa atumiki.
142. Pamene m'bale wawo
Swaleh Adawauza kuti: "Kodi
simuopa (Mulungu)
143. Ndithu, ine ndimtumiki
wokhulupirika Kwa inu.
144. Choncho muopeni
Mulungu ndipo Mverani ine.
145. Ndipo sindikupemphani
malipiro Pazimenezi. Palibe
kumene kuli Malipiro anga koma
kwa Mbuye Wazolengedwa.
146. Kodi (mukuganizira kuti)
mudzasiidwa Mwamtendere pa izi
zili pano (Popanda imfa
kukudzerani?)
147. M'minda ndi muakasupe,
-■mim&a
®*£$£&4$&j
^\''>\>'>\,''?<(
a.^ w\>''*h't
^ssw
W^&4$2fc
'»<\\\>» '
*.-> V
S&JfyE&SBS
Surat 26. Ash-Shu'ara Juzu 19
790
> ^ «.j*-i r n *\jl^\ «j>-»
148. Ndi (m'minda) yammera
ndi mitengo Yakanjedza yamikoko
yakupsa yofewa?
149. Ndipo mukujoba nyumba
m'mapiri Mwaluso.
150. Choncho muopeni
Mulungu ndipo Ndimvereni.
151. Ndipo musamvere za awo
opyola malire,
152. Amene akuononga
padziko, ndipo Sakonza."
153. (Iwo) adati: "Ndithu, iwe
ndi mmodzi Wa olodzedwa.
154. Iwe suli kanthu, koma
munthu ngati ife; Tabwera ndi
chozizwitsa, ngati Ndiwedi
mmodzi wa onena zoona!"
155. (lye) adati:
"(Ndakubweretserani) Ngamira iyi
yaikazi; (koma) ikhale Ndi gawo
lake lakumwa, ndipo inu
Mukhalenso ndi gawo lanu
lakutunga (Madzi) patsiku
lodziwika. (Tsiku Lina lotunga
madzi anthu).
156. Ndipo musaikhudze ndi
choipa chilichonse Kuopera kuti
chingakupezeni chilango cha Tsiku
lalikulu."
157. Koma iwo adaipha; ndipo
adali odandaula (Pamene chidadza
Chilango cha Mulungu).
*e&i$3Bsa;
Surat 26. Ash-Shu'ara Juzu 19
791
M *>l Yn ^lyt^JlSjj--
158. Choncho chilango cha
Mulungu Chidawaononga ndithu,
pazimenezi pali Phunziro; koma
ambiri aiwo sadali Okhulupirira.
159. Ndipo, ndithu, Mbuye
wako, lye Ngwamphamvu zoposa;
Wachisoni
160. Anthu a Luti adatsutsa
atumiki.
161. Pamene m'bale wawo Luti
Adanena kwa iwo (kuti): "Kodi
Simuopa (Mulungu)?
162. Ndithu, ine ndine Mtumiki
Wokhulupirika kwa inu.
163. Choncho muopeni
Mulungu ndipo Ndimvereni
164. Ndipo sindikupemphani
malipiro Pazimenezi; palibe
komwe kuli malipiro Anga koma
kwa Mbuye wazolengedwa.
165. Kodi mukugonana ndi
amuna (anzanu) Muzolengedwa
(za Mulungu),
166. Ndikusiya amene Mbuye
wanu Adakulengerani kuti akhale
akazi anu? Ndithu, inu ndinu anthu
Olumpha malire."
167. (Iwo) adati: "Ngati susiya
(izi), E, iwe Luti! ndithu, ukhala
mmodzi Wa opirikitsidwa."
168. (lye) adati: "Ndithu, ine
ndine m'modzi Wakuzida izi
A'tfiu*
Surat 26. Ash-Shu'ara Juzu 19
792
>* ftjJt-i Yn tiyuiJidj^-
zochita zanu (choncho Sindisiya
kuzidzudzula).
169. E, Mbuye wanga!
Ndipulumutseni ine Ndi banja
langa ku (matsoka a) zimene
Akuchita.!"
170. Ndipo tidampulumutsa iye
ndi onse a pa Banja lake,
171. Kupatula nkhalamba
yaikazi (imene Idasankha kukhala)
mwaotsalira pambuyo.
172. Titatero tidawaononga
enawo.
173. Ndipo tidawavumbwitsira
mvula (yamiyala); Iyipirenji,
mvula Ya ochenjezedwa!
174. Ndithu, pazimenezi pali
malingaliro. Koma ambiri a iwo
Sadali okhulupirira.
175. Ndipo, ndithu, Mbuye
wako, Ngwamphamvu Kwambiri;
Ngwachisoni.
176. Anthu a m'dziko
lamitengo yambiri (Madiana)
adatsutsa atumiki.
177. (Akumbutse) pamene
(Mneneri) Shuaibu adati kwa iwo:
"Kodi Simuopa (Mulungu)?
178. Ndithu, ine ndine Mtumiki
Wokhulupirika kwa inu.
179. Choncho muopeni
Mulungu ndipo Ndimvereni
%&&asof$
Surat 26. Ash-Shu'ara Juzu 19
793 > * *ji-i t *\ tiytJJi djj--
180. Ndipo sindikupemphani
malipiro Pazimenezi; kulibe
malipiro anga Koma kwa
(Mulungu) Mbuye wa zolengedwa.
181. Kwaniritsani mulingo
(pamalonda pamene Mukupima),
ndipo musakhale mwaopungula
(Mulingo).
182. Ndipo yesani ndi sikelo
yolungama (Yolondola).
183. Ndipo musawachepetsere
anthu zinthu Zawo, ndiponso
musayende padziko uku
Mukuononga.
184. Ndipo muopeni amene
adalenga inu Ndiponso
zolengedwa zoyamba (zimene
Zidanka kale)"
185. (Iwo) adati: "Ndithu, iwe
ndi mmodzi Wa olodzedwa.
186. Ndipo iwe suli kanthu
koma munthu ngati Ife, ndipo
ndithu, tikukutsimikizira Kuti
ndiwe mmodzi wa abodza.
187. Choncho tigwetsere
zidutswa za thambo (Kuti
zitiononge) ngati uli mmodzi Wa
onena zoona."
188. (Shuaibu) adati: "Mbuye
wanga Ngodziwa kwambiri
zimene mukuchita. (Akadzaona
kuti inu ngoyenera Kulangidwa
m<sjZv$&&$&ts
®^\g>
&(*^&1&%3^%\
K hr
&2t > 4
<y$
<&&&$&$
Siirat 26. Ash-Shu'ara Juzu 19 794 ^ S *jfci y n f.\yjJ\ Sj^
ndizidutswa za thambo,
Adzakulangani).
189. Koma adamutsutsa. Ndipo
chidawagwera Chilango chatsiku
la mthunzi; ndithu, Chimenecho
chidali chilango cha Tsiku lalikulu.
190. Ndithu, pazimenezi pali
lingaliro; Koma ambiri a iwo
sadali okhulupirira.
191. Ndipo, ndithu, Mbuye
wako Ngwamphamvu kwambiri;
Ngwachisoni.
192. Ndipo, ndithu iyi (Qur'an)
ndiyo chivumbulutso Cha Mbuye
wazolengedwa zonse.
193. Mzimu Wokhulupirika
(Jiburil) Udaivumbulutsa.
194. Pamtima wako kuti ukhale
mmodzi wa Achenjezi,
195. M'chilankhulo cha
Chiarabu chomveka Bwino.
196. Ndipo ndithu, izi (zomwe
zili m'Qur'an) Zilipo m'mabuku
akale.
197. Kodi sipadapezeke
chisonyezo kwa iwo Kuti
akuidziwa (Qur'an) odziwa mwa
ana A Israeli? (Kotero kuti ena
alowa M'Chisilamu).
198. Ndipo tikadaivumbulutsa
kwa wina Amene sali Muarabu,
Surat 26. Ash-Shu'ara Juzu 19 I 795 I ^ ^ *>i r n tiyuiJi «jj-*
199. Kotero kuti
nkuwawerengera momveka
Bwino, sakadaikhulupirira.
200. Momwemo ndimo
tidalowetsera kuitsutsa (Qur'an)
m'mitima ya oipa.
201. Sangaikhulupirire kufikira
ataona Chilango chowawa.
202. Ndipo chidzawadzera
mwadzidzidzi Asakuzindikira;
203. Adzayamba kunena: "Kodi
ife tipatsidwa Nthawi (yoti tilape)?"
204. Kodi akuchifulumizitsa
chilango Chathu?
205. Kodi ukuona bwanji, ngati
Titawasangalatsa zaka
(zankhaninkhani)
206. Kenako nkuwadzera
(chilango) chomwe Adalonjezedwa,
207. Sizidawathandize zomwe
Adali kusangalatsidwa nazozo?
208. Ndipo sitidauononge
Mudzi uliwonse koma Udali ndi
achenjezi,
209. (Kuti akhale) chikumbutso.
Ndipo Sitidali osalungama
(powaononga Popanda
kuwachenjeza).
210. Ndipo Asatana
sadaivumbulutse (iyi Qur'an
monga osakhulupirira Akunenera
monyoza).
fei-^^^t
*]>w
<%^v$a^^
^0S^Z3^&M
%>g®$$&M
%&&*$&»
Surat 26. Ash-Shu'ara Juzu 19
796
1 * frj^rl T 1 tlyuiJl 5jj--
211. Ndipo sikoyenera kwa iwo
(Kuivumbulutsa Qur'an) ndiponso
sangathe.
212. Ndithu, iwo
ngotsekerezedwa Kumvetsera
(zimene angelo Amalankhula
kumwamba).
213. Choncho usapembedze
mulungu wina Pamodzi ndi
Mulungu, kuti usakhale Mwa
olangidwa.
214. Ndipo achenjeze abale ako
apafupi,
215. Ndipo fungatira ndi phiko
lako amene Akutsata mwa
okhulupirira.(Ukhale wachifundo
kwa iwo).
216. Ngati atakunyoza, nena:
"Ine ndili Kutali ndi zimene
Mukuchitazo."
217. Ndipo tsamira kwa
(Mbuye wako) Mwini Mphamvu
zoposa; Wachisoni
218. Yemwe akukuona pamene
ukuimirira (Pamapemphero),
219.Ndikutembenukatembenuka
kwako (Pogwetsa mphumi yako
pansi ndi Kudzuka ndikuimirira)
pamodzi ndi Ogwetsa mphumi
pansi (polambira Mulungu).
220. Ndithu, lye Ngwakumva;
Ngodziwa Chilichonse.
%s&&*yjii&&
k£&v$\<£&
^0€&&'^3
%&*£&?&£
o^Xg&vk
Surat 26. Ash-Shu'ara Juzu 19
797
\ * *j*-l Y 1 *iyuiJl Sjj^
221. Kodi ndikuuzeni amene
asatanaAmawatsikira?
222. Amamtsikira yense
wabodza Lamkunkhuniza;
wamachimo.
223. Amawaponyera (asatana
anzawo a mu anthu) Zimene
azimva. Koma ambiri a iwo
Ngabodza.
224. Ndipo alakatuli (olakatula
zopanda Phindu) amatsatidwa ndi
(anthu) Opotoka.
225. Kodi suona kuti iwo
akungoyumbayumba M'chigwa
chilichonse (Chamawu)?
226. Ndithunso, iwo akunena
zomwe sachita;
227. Kupatula amene
akhulupirira Ndikumachita
zabwino, ndikumamtchula
Mulungu mowirikiza,
ndikuzipulumutsa Okha pambuyo
pochitiridwa zoipa. Ndipo
posachedwa amene adzichitira
Okha zoipa adziwa Kotembenukira
komwe adzatembenukire.
®
Surat 27. An-Naml Juzu 19 798 ) ^ ^jA-i t V J^Ji 5jj--
Surayi ikufotokoza nkhani ya Musa ndi zozizwitsa zake ndi
nkhani ya Daudi, ndi kuti Sulaiman adalowa m'malo mwa
Daudi. Ndipo yafotokozanso kuti ziwanda, anthu ndi mbalame
zimasonkhanitsidwa ndi kugonjera zofuna za Sulaiman. Ikutinso
iye amazindikira ziyankhulo za nyama, potero amayamika
Mulungu kwambiri yemwe adamzindikiritsa ziyankhulozo.
Surayi yafotokozanso zakusowa kwa mbalame yotchedwa
Huduhudu ndi kudza kwake ndi nkhani ya Bilikisi yemwe ndi
anthu ake adali kupembedza dzuwa, komanso Sulaiman atamva
zimenezo adamtumizira kalata, ndipo Bilikisi pofuna kuyankha
kalatayo adangotumiza mitulo. Izi zidachitika atakhala upo ndi
anthu ake. Ndipo yafotokozanso kuti mpando wachifumu wa
Bilikisi adabwera nawo kwa Sulaimani iye mwini asadadze,
kupyolera m'mphamvu za wodziwa zam'buku. Komanso surayi
ikufotokoza nkhani yakulowa kwa Bilikisi m'nyumba ya
Sulaiman imene idamudabwitsa.
Surayi yafotokozanso nkhani ya Swaleh pamodzi ndi anthu
ake, ndi nkhani ya Luti pamodzi ndi anthu ake ndi kuti iye ndi
banja lake adapulumuka kuchionongeko kupatula anthu oipa.
Surayi ikudzutsa maganizo athu kuti tiyang'ane zakumwamba
ndi zapansi pano zomwe zikusonyeza kukhoza ndi mphamvu za
Mulungu. Ndiponso yafotokoza za ulemerero wa Qur'an; Qur'an
yomwe ikuitanira ku njira yolunjika. Koma otsutsa akunyozera
ulaliki wa Qur'an yomwe ikufotokoza kuti m'nthawi yakutha
dziko lapansi kudzatuluka chinyama chomwe chidzakhala
chikuwayankhula anthu kuti iwo samatsimikizira zisonyezo za
Mulungu. Kenako surayi yakumbutsa anthu kuti kudzakhala
zoopsa lipenga lakutha kwadziko likadzaimbidwa ndi kuti
nthaka idzagwedezeka zolimba ndipo mapiri adzakhala akuyenda
monga mitambo. Pomaliza surayi yalangiza Mtumiki (madalitso
ndi mtendere zikhale naye) njira imene angatsate pa utumiki wake.
Siirat 27. An-Naml Juzu 19
799
S<\ tjir\
rv j^JiSj^
SuratAl-Naml XXVII
M'dzina la Mulungu waChifundo
Chambiri, waChisoni.
1. Td-Sin. Izi ndi aya (ndime)
(za Qur'an Buku lodzazidwa ndi
zothandiza), Ndiponso buku
lofotokoza (chilichonse Chauzimu
ndi chamoyo wadziko);
2. (Qur'an) nchiongoko ndi
nkhani yabwino Kwa okhulupirira,
3. Amene akupemphera swala
(zisanu, Modzichepetsa ndi
mokwaniritsa malamulo Ake) ndi
kumapereka zakati (m'nthawi
yake), Ndipo iwo ali ndi
chitsimikizo champhamvu Cha
(moyo wa) tsiku lachimaliziro.
4. Ndithu, amene sakhulupirira
za (moyo wa) Tsiku la chimaliziro,
takometsa kwa iwo Zochita zoipa
kukhala ngati zabwino; Choncho
iwo akungoyumbayumba
(m'kusokera Kwawo).
5. Iwowo ndiamene adzapeza
chilango choipa; Iwo tsiku
lachimaliziro ngotayika zedi,
(Adzaonongeka kumoto motheratu).
6. Ndipo ndithu, iwe
ukuphunzitsidwa Qur'an
Kuchokera kwa Mwini nzeru
zakuya, Wodziwa kwambiri.
mm.
M
oj&£\<J£-3^j
-w
%l^^^:i^np
Surat 27. An-NamI Juzu 19
800 ^ *>»
tV J-JlSjj^
7. (Kumbuka) Musa pamene
adauza banja lake (Mkazi wake):
"Ndithu, ine ndaona moto;
Posachedwapa ndikubweretserani
nkhani, Zakumeneko kapena
ndikubweretserani Chikuni
chamoto kuti inu muothe.
8. Ndipo pamene adaudzera
(motowo) Kudaitanidwa:
"Wadalitsidwa yemwe ali M'moto
ndi yemwe ali m'mphepete
mwake; Ndipo walemekezeka
Mulungu Mbuye wazolengedwa.
9. E, iwe Musa! Ndithu, ine
ndine Mulungu, Wamphamvu
zoposa; Wanzeru zakuya.
10. Ndipo ponya (pansi) ndodo
yako! (Pamene adaiponya
idasanduka njoka), Pamene
adaiwona ikugwedezeka (ndodo
ija) Ngati njoka, adatembenuka
kuthawa, Ndipo sadacheuke
(kapena kudikira kuti Amve mawu
omvekawo): "E, iwe Musa!
Usaope. Ndithu Ine, saopa Kwa
Ine atumiki.
11. Koma amene wadzichitira
yekha zoipa, Kenako nkusintha
(pochita) zabwino pambuyo Pa
zoipa, (ndimkhululukira) pakuti
Ine ndine Wokhululuka kwabasi,
Wachifundo chambiri.
12. Ndipo lowetsa dzanja lako
palisani la mkanjo Wako, ndipo
by* usjoU*^O^V^(^j)J
{$9 4f9*t< 9\\<
9 /('.'"WC Si ,*9- '\" 9 \ *'Y
Surat 27. An-Naml Juzu 19
801
>*\ «.j4-i
TVj^JlSj^
lituluka lili loyera, (kuyera)
kopanda Matenda. (Ziwirizi) zili
m'gulu la Zododometsa zisanu ndi
zinayi. Pita nazo kwa Farawo ndi
anthu ake; ndithu, iwo ndianthu
Otuluka m'chilamulo cha Mulungu."
13. Pamene zidawadzera
zizindikiro zathu Zosonyeza (kuti
iye ndimtumiki wa Mulungu)
adati: "Awa ndimatsenga
woonekera."
14. Ndipo adazitsutsa
(zisonyezozo) mwachinyengo Ndi
modzikuza chikhalirecho mitima
yawo Idatsimikiza (kuti ndizoona
zochokera Kwa Mulungu);
choncho, yang'ana adali Bwanji
malekezero a oononga!
15. Ndipo ndithu, Daudi ndi
Sulaiman tidawapatsa Nzeru
(zazikulu; adayamika Mulungu)
adati: "Kuyamikidwa konse
kwabwino nkwa Mulungu Yemwe
watichitira ubwino kuposa Ambiri
mwa akapolo ake okhulupirira."
16. Ndipo Sulaiman adalowa
mmalo mwa Daudi panzeru ndi
uneneri ndipo (Sulaiman) Adati:
"E,inu anthu! Ndithu,
taphunzitsidwa (Mpaka tikudziwa)
chiyankhulo cha mbalame,
Ndiponso tapatsidwa chilichonse;
ndithu, Umenewu ndiufulu
wopenyeka.
9 -»<
Surat 27. An-Naml Juzu 19
802
>* *>i
XV J^JlSj^
17. Ndipo adasonkhanitsidwa
kwa Sulaiman Ankhondo ake
ochokera m'ziwanda, anthu Ndi
mbalame,ndipo adawandandika
M ' magulumagulu,
18. Kufikira pamene adadza
pachigwa chanyerere, Nyerere
idanena (kuuza zinzake): "E, inu
Nyerere, lowani m'nyumba zanu
poopa kuti Angakupondeni
Sulaiman ndi magulu ake
Ankhondo pomwe iwo sakudziwa
(za inu)."
19. Ndipo adamwetulira,
kuseka, chifukwa cha Mawu ake
aja (mawu a nyerere); ndipo
(Sulaiman) adati: "E, Mbuye
wanga! Ndipatseni nyonga zakuti
ndizithokozera Mtendere wanu
umene mwandidalitsa nawo
Pamodzi ndi makolo anga, ndi kuti
Ndizichita zabwino (zomwe)
mukuziyanja; Kupyolera
m'chifundo chanu, ndiponso
Ndilowetseni m'gulu la akapolo
anu abwino."
20. Ndipo adayamba kuyendera
Mbalame, adati: "Kodi bwanji
Sindikumuona Huduhudu? Kapena
ali m'gulu la Amene pano palibe?
21. "Ndithu, ndithu,
ndimulanga chilango Chokhwima,
kapena ndimzinga (ndimdula
Khosi) pokhapokha andibweretsere
S^&ajssgagi
Siirat 27. An-Naml Juzu 19
803
H *><
YV J^JlSjj-
umboni Womveka (wosonyeza
kuti adachoka Pazifukwa
zomveka)."
22. Ndipo (Huduhudu)
sadakhalitse nthawi Yaitali; ndipo
adati (kwa Sulaiman):
"Ndatulukira zomwe iwe
sudazitulukire, Ndipo
ndakubweretsera nkhani
yotsimikizika Kuchokera ku Saba.
23. Ndithu, ine ndapeza mkazi
akuwalamulira (Anthu akudziko la
Saba), ndipo wapatsidwa
Chilichonse; ndipo ali ndi
chimpando Chachikulu chachifumu.
24. Ndampeza iye ndi anthu ake
akulambira Dzuwa kusiya
Mulungu; ndipo Satana
Wawakometsera zochita Zawo
zoipa; choncho wawatsekereza
Kunjira yolungama, tero
Sadaongoke.
25. Kuti asamlambire Mulungu
yemwe Amatulutsa zobisika
kumwamba ndi pansi; Ndipo
akudziwa zimene mukubisa ndi
zimene Muonetsa poyera.
26. Mulungu! Palibe wina
wopembedzedwa Mwachoona
koma Iye basi; Mbuye wa Mpando
Waukulu."
27. (Sulaiman) adati "Tiona
ngati wanena Zoona kapena (ngati)
uli m'gulu laonama.
{^^^(Mo^^^ijS
Surat 27. An-Naml Juzu 19
804 I 1 * ^>»
rvj^Jioj^
28. Pita ndi kalata yangayi,
kaiponye kwa iwo; Kenako
ukadzipatule kwa iwo (ukakhale
Pambali) ndi kuona momwe
azikayankhira."
29. (Mfumukazi) idati: "E, inu
nduna! Ndithu, Kalata
yolemekezeka Yaponyedwa kwa
ine.
30. Yachokera kwa Sulaiman,
ndipo mawu ake Ndi awa: M'dzina
la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni.
31. Musadzikweze kwa ine,
Ndipo idzani kwa ine Muli
ogonjera malamulo anga."
32. (Mfumukazi idaonjezera)
kunena: "E, inu, Nduna!
Ndilangizeni pankhani yangayi;
Sindilamula kanthu mpaka inu
Mutandibwerera."
33. (Nduna) zidati: "Ife ndife
eni nyonga ndi eni Kumenya
nkhondo mwaukali; koma zonse
Zili ndi inu; choncho yang'anani
mmene Mungalamulire."
34. (Mfumukazi) idati: "Ndithu
mafumu Akamalowa m'mudzi (wa
anthu), Amauononga motheratu,
ndi kuwachita Olemekezeka
am'menemo kukhala Onyozeka.
Mmenemo ndimomwe amachitira
(Nthawi zonse).
k&^&ffiM
Surat 27. An-Naml Juzu 19
805
^ fr>*
rvjuJUj^
35. Koma ine nditumiza mitulo
kwa iwo ndi Kuyembekezera
zimene abwere nazo
Otumidwawo."
36. Pamene adafika
(wamthenga wamkulu) kwa
Sulaiman (ndi kupereka mphatso
zija, Sulaiman adazikana) nati:
"Mukundithandiza Ndi chuma?
Zimene Mulungu wandipatsa
Ndizabwino kuposa zimene
wakupatsani. Koma inu
mukusangalala ndi mphatso zanu.
37. Bwerera (nazo) kwa iwo;
ndithu, tiwadzera Ndi gulu
lankhondo lomwe iwo sangathe
Kulimbana nalo; mtheradi,
tikawatulutsa M'menemo ali
onyozeka ndi oyaluka,"
38. (Sulaiman adasonkhanitsa
nduna zake) Nati: "E, inu nduna!
Ndani abwere ndi Mpando
wakewo kwa ine asadandidzere Ali
ogonja"?
39. Chiwanda chautambwali
chidati: "Ine Ndikubweretsera
chimenecho usadaimirire Pamalo
ako (oweruzira). Ndipo ndithu, ine
Pa icho (chimpando) ndine
wanyonga, Wokhulupirika.
40. Yemwe adali ndi
maphunziro (akuya) Am'buku
adati: "Ine ndikubweretsera
(Chimpandocho) maso ako
%K 9> 9? \'
iW&MS^S^
erg"''^'
Surat 27. An-Naml Juzu 19
806
^ *>»
rv j^JiSjj--
asadaphetire (Usadatsinzine ndi
kupenya)." Pamene Adachiona
chitakhazikitsidwa patsogolo Pake,
adati: "Izi nchifukwa cha ufulu Wa
Mbuye wanga kuti andiyese
mayeso kodi Ndithokoza kapena
ndiusuliza (ufulu Wake). Ndipo
amene akuthokoza ndithu, ubwino
wa Kuthokozako udzakhala pa iye
mwini. Ndipo amene akukana
(mtendere wa Mulungu
Posathokoza), ndithu, Mbuye
wanga Ngokhupuka; Waulemu,
(sasaukira Chilichonse kwa anthu)."
41. (Sulaiman) adati:
"Msinthireni (Maonekedwe a)
mpando wakewo kuti tione Kodi
auzindikira kapena akhala mwa
omwe Sazindikira (chinthu).
42. Choncho pamene
(mfumukazi) idadza,
Kudanenedwa: "Kodi mpando
Wako wachifumu uli ngati uwu?"
Idati, "Uli ngati umenewu, ndithu,
ndipo ife Tidapatsidwa kuzindikira
(Za uneneri wanu) tisadaone
chozizwitsa Ichi; ndipo, ndithu
tidadzipereka (kwa Mulungu).
43. Ndipo (Sulaiman)
adamuletsa zomwe
Amazipembedza kusiya Mulungu.
Ndithu (mfumukaziyo) idali Mwa
anthu osakhulupirira (Mulungu).
44. (Mfumukazi ija) idauzidwa
kuti: "Lowa M'nkhonde la
%y&?jS\Jfr\V&
Surat 27. An-Naml Juzu 19
807
><\ t&\
rv j^JiSj^
nyumba" koma pamene Adaliona
adaliganizira kuti ndidziwe;
Adakweza nsalu kumiyendo yake.
(Sulaiman) Adati: "Ndithu,
limeneli ndinkhonde lomwe
Laziridwa ndi magalasi."
(Mfumukazi) Idati: "E, Mbuye
wanga! Ndadzichitira Ndekha
chinyengo; choncho, ndagonjera
Kwa Mulungu, Mbuye
wazolengedwa Pamodzi ndi
Sulaiman."
45. Ndipo ndithu,Asamudu
tidawatumizira M'bale wawo
Swaleh kuti awauze:
"Mpembedzeni Mulungu".Choncho
adali Magulu awiri omwe
amakangana.(Ena adam'tsata
Pomwe ena adam'kana).
46. (Swaleh) adati: "E, inu
anthu anga chifukwa Ninji inu
mukufulumizitsa choipa (kuti
Chidze) musanachite chabwino?
Bwanji Simukupempha
chikhululuko kwa Mulungu Kuti
muchitiridwe chifundo?"
47. (I wo) adati: "Tapeza
masoka oipa chifukwa Cha iwe ndi
omwe uli nawo." (lye) adati:
"Tsoka lanu lili kwa Mulungu
(chifukwa cha Zolakwa zanu);
koma inu ndinu anthu amene
Mukuyesedwa (ndi Mulungu kuti
aone ngati Mutsatire Mtumiki
wake kapena simutsatira)".
Siirat 27. An-Naml Juzu 19
808
H *>t
YV J^JlSjj-
48. Ndipo m'mudzimo adalipo
anthu asanu ndi Anayi omwe
amaononga padziko, ndipo
Samakonza (chilichonse koma
kuchiononga).
49. (Iwo) adati: "Aliyense wa
ife alumbire kwa Mulungu (kuti)
iye (Swaleh) ndi banja lake
timthira Nkhondo usiku, ndipo
kenako Timuuza mlowam'malo
wake (kuti): "Sitidaone
kuonongeka Kwa m'bale wake;
Ndithu, ife tikunena zoona."
50. Ndipo adakonza chiwembu
ndi kutchera Misampha
yamphamvu, nafenso tidawatchera
Misampha yowaononga, iwo
asakudziwa.
51. Tsono tayang'ana, kodi
malekezero Achiwembu chawo
adali otani! Tidawaononga iwo ndi
anthu awo onse.
52. Izo ndinyumba zawo
(zomwe zasanduka) Mabwinja
chifukwa cha chinyengo chawo.
Ndithu, m'zimenezo muli phunziro
kwa Odziwa.
53. Ndipo tidawapulumutsa
amene adakhulupirira Pakuti
amamuopa Mulungu.
54. Ndipo (akumbutse nkhani
ya) Luti pamene Adanena kwa
anthu ake: "Kodi mukuchita
Zadama uku inu mukuziona?
Siirat 27. An-Naml Juzu 20
809
**'
tVj^JUj^
55. Kodi inu mukugona ndi
amuna pokwaniritsa Chilakolako
(cha chilengedwe) kusiya Akazi?
koma inu ndinu mbuli."
56. Koma anthu ake sadayankhe
yankho Una Koma ili (lakuti):
"Apirikitseni otsatira Luti
M'mudzi mwanumu; ndithu, iwo
ndianthu Odziyeretsa (asakhale
Pamodzi ndi ife adama)."
57. Choncho tidampulumutsa
iye ndi otsatira Kupatula mkazi
wake; tidamlingira kukhala
Mmodzi mwaotsalira (kuti
aonongedwe Pamodzi ndi
oonongedwa, chifukwa cha
Ntchito zake zoipa ngakhale kuti
adali mkazi Wa mneneri).
58. Ndipo tidawavumbwitsira
mvula (yamiyala); Iipirenji mvula
ya ochenjezedwa (Koma
osachenjezeka)!
59. Nena: "Kuyamikidwa konse
kwabwino nkwa Mulungu, ndipo
mtendere ukhale pa akapolo Ake
omwe adawasankha. Kodi
wabwino Ndi Mulungu kapena
zimene akumphatikiza Nazozo?
60. (E, iwe Mtumiki! Pitiriza
kuwafunsa) Kodi kapena
(wabwino) ndiamene adalenga
Thambo ndi nthaka (ndi
zam'menemo) ndi Kukutsitsirani
mvula (yothandiza) kuchokera
&r.; v
Surat 27. An-NamI Juzu 20
810
*>i
TV J-J»Sj>-»
Kumwamba,choncho ndi madziwo
Timameretsa madimba okongola.
Inu Simungathe kumeretsa
mitengo yake. Kodi Pamodzi ndi
Mulungu pali mulungu (wina)?
Koma iwo (Akafiri) ndi anthu
opotoka.
61. Kodi kapena (wabwino)
ndiamene adapanga Nthaka
kukhala malo okhazikika ndi kuika
Mitsinje pakati pake ndi
kuipangira mapiri, Ndi kuika
chitsekerezo pakati panyanja
Ziwiri (nyanja yamadzi amchere,
ndi yamadzi Ozizira)? Kodi
pamodzi ndi Mulungu pali
Mulungu wina? Koma ambiri a
iwo sadziwa.
62. Kapena (wabwino)
ndiyemwe amamuyankha
Wozunzika akamampempha ndi
kumchotsera Masautso ake ndi
kukuchitani inu kukhala Oyendetsa
dziko lapansi? Kodi pamodzi ndi
Mulungu pali mulungu wina?
Ndithu, kulangika kwanu nkochepa.
63. Kapena (wabwino)
ndiyemwe Amakuongolerani
mumdima wapamtunda Ndi
panyanja ndi kutumiza mphepo
kuti Ikudzetsereni nkhani yabwino
patsogolo Pa chifundo chake
(mvula isanagwe)? Kodi pamodzi
ndi Mulungu pali mulungu Wina?
Mulungu watukuka Kuzimene
akumuphatikiza nazo.
Surat 27. An-Naml Juzu 20
811
*>'
TV J^Jtojj-
64. Kapena (wabwino) ndiamene
adayambitsa Zolengedwa, (ndipo)
kenako adzazibweza, Kapenanso
amene amakupatsani riziki
(Chakudya) kuchokera
kumwamba ndi M'nthaka? Kodi
pamodzi ndi Mulungu pali
Mulungu winanso? Nena:
"Bweretsani Umboni wanu ngati
mukunena zoona (Wotsimikizira
kuti Mulungu ali Ndi mnzake)".
65. Nena: "Palibe amene alipo
kumwamba ndi Pansi akudziwa
zam'seri (zomwe zisanadze)
Kupatula Mulungu basi. Ndipo
(amene Akuwapembedza) sadziwa
kuti nliti Adzaukitsidwa ku imfa.
66. Kwakhwima liti kudziwa
kwawo (Zakudza) kwa tsiku la
chimaliziro? Koma iwo ali
mchikaiko ndi za tsikulo; Koma
iwo ngakhungu pazatsikulo.
67. Ndipo adanena omwe
adatsutsa (za Mulungu): "Kodi
tikadzakhala dothi, ife ndi makolo
athu Akale, (nzoona)
tidzatulutsidwanso (M'manda tili
amoyo)?
68. Ndithu, tidalonjezedwa izi,
ife ndi makolo Athu kale, izi
sichina koma ndi nthano (Zabodza)
za anthu akale."
69. Nena: "Yendani padziko Ndi
kuona momwe adalili mapeto a oipa".
\&? v>J V )3 (y^VjUh Genual
Siirat 27. An-Naml Juzu 20 812 Y • *jk-\
rvjuJiajj--
70. Ndipo usawadandaulire,
ndiponso usakhale Wobanika
chifukwa cha ziwembu zomwe
Akuchita.
71. Ndipo (iwo) akuti: "Kodi
lonjezoli Lidzachitika liti, ngati
Mukunena zoona?"
72. Nena: "Kapena zina mwa
zomwe Mukuzifulumizitsa zili
Pafupi kukupezani."
73. Ndipo, ndithu, Mbuye wako
ndi mwini Kupereka ufulu
(waukulu) kwa anthu; koma
Ambiri a iwo sathokoza.
74. Ndipo ndithu, Mbuye wako
akudziwa zomwe Zikubisa zifuwa
zawo ndi zomwe Akuonetsera
poyera.
75. Ndiponso palibe chobisika
kumwamba ndi M'nthaka koma
chili m'buku lofotokoza Chilichonse.
76. Ndithu, Qui*' an iyi,
ikufotokoza kwambiri Za ana a
Israeli pazambiri zomwe iwo
Akutsutsana.
77. Ndipo ndithu, iyi (Qur'an)
ndichiongoko ndi Chifundo kwa
okhulupirira.
78. Ndithu, Mbuye wako
adzalamula pakati Pawo ndi
chiweruzo chake (choona); ndipo
lye Ngwamphamvu zoposa
Ngodziwa Chilichonse.
©tw:
?>>\*?s
fit'/ 9 I *»"\\\< \ l' s*\>l-
•s'
Surat 27. An-Naml Juzu 20
813
Y* ij±\
TV JuJidj^-
79. Choncho tsamira kwa
Mulungu; ndithu, iwe uli panjira
Yachoonadi yoonekera.
80. Ndithu,iwe sungathe
kuwachititsa kuti amve Kuitana
kwako akufa, ndiponso sungathe
Kuwachititsa kuti agonthi amve
kuitanako, Pamene akucheuka
kutembenuza misana (Osafuna
kumva ulaliki wako).
81. Ndiponso suli owaongola
akhungu M'kusokera kwawo,
ndipo sungachititse Kuti amve
(uthenga wako) kupatula yemwe
Akukhulupirira aya (ndime) Zathu;
iwowo Ndiwo ogonjera malamulo
(Athu).
82. Ndipo mawu (onena Kudza
kwa Kiyama) Akadzatsimikizika
pa iwo, Tidzawatulutsira nyama
m'nthaka imene Idzawayankhula
kuti ndithu, anthu adalibe
Chitsimikizo pa aya (ndime) Zathu.
83. Ndipo (akumbutse za) tsiku
lomwe Tidzasonkhanitsa
magulumagulu Mum'badwo
uliwonse omwe amatsutsa Aya
(ndime) Zathu. Ndipo Iwo
adzakhala magulumagulu.
84. Kufikira pomwe adzaza;
(Mulungu) adzati: "Kodi inu
mudazitsutsa aya (ndime) Zanga
Popanda kuzidziwa bwinobwino,
Nanga mumachita chiyani?"
Siirat 27. An-Naml Juzu 20
814
*>>
TV J^Jl 5jj--
85. Ndipo mawu onena za
kuonongeka Adzatsimikizika pa
iwo, chifukwa cha Chinyengo
chawo (chodzichitira okha) Ndipo
iwo sadzawiringula.
86. Kodi saona kuti Ife tapanga
usiku ndi Cholinga chakuti
apumule m'menemo, Ndinso usana
woyera (kuti aone)? Ndithu Mu
zimenezo muli zizindikiro Kwa
anthu okhulupirira.
87. Ndipo (akumbutse za) tsiku
limene lipenga (La chiweruzo)
lidzaimbidwa, Adzadzidzimuka
amene ali kumwamba Ndi amene
ali pansi kupatula yemwe Mulungu
wamfuna (kuti Asayumbeyumbe);
ndipo onse Adzam'dzera (Mulungu)
ali odzichepetsa (Ofooka).
88. Ndipo ukuona mapiri ndi
kuwaganizira kuti Akhazikika
pomwe akuyenda kuyenda kwa
Mitambo. Chimenecho
ndichikonzero cha Mulungu
chimene adakonzera chinthu
Chilichonse. Ndithu Mulungu
akudziwa Zonse zimene muchita.
89. Amene adzaza ndi
chabwino, adzalandira Mphoto
yoposa chabwinocho; Ndikuopsa
kwa tsiku limenelo, Iwo adzakhala
nako mwamtendere.
90. Koma amene adzaza ndi
choipa, Adzaponyedwa kumoto
&zm$®v%&>
Surat 27. An-Naml Juzu 20
815 I T * *>»
YV J*Jl5j>*
champhumi, "Kodi mulipidwa
(china) Osati zomwe mumachita?"
91. Ndithu, ndalamulidwa
kumpembedza Mbuye wa mzinda
uwu, yemwe Adaukhazika
wopatulika. Ndipo Zinthu zonse
nza lye (Mulungu), ndipo
Ndalamulidwa kukhala mmodzi
Wa ogonjera (Mulungu),
92. Ndiponso (ndalamulidwa)
kuti ndiwerenge Qur'an; ndipo
amene waongoka, ubwino
Wakuongokako uli pa iye; ndipo
amene Wasokera, (wadzisokeretsa
yekha). Nena: "Ndithu, ine
sikanthu koma ndine mmodzi Wa
achenjezi. (ndilibe udindo wina
Woposa uwu)."
93. Ndipo nena: "Kuyamikidwa
konse (kwabwino) Nkwa
Mulungu; posachedwapa
akusonyezani Zizindikiro Zake,
ndipo muzizindikira". Ndipo
Mbuye wako sali wamphwayi ndi
Zimene mukuchita.
Siirat 28. Al-Qasas Juzu 20 816 * % frj*-' * A ^a^Ji s^
ikufotokoza mwatsatanetsatane nkhani ya Musa
kuyambira pamene adabadwa, m'nthawi ya ufumu wa Farawo.
Ndipo panthawiyo Farawo amapha ana achimuna a ma Isiraeli
poopera kuti mwa iwo mungadzatuluke Mneneri amene
angathetse ufumu wake. Koma mwa mphamvu za Mulungu,
Musa sadaphedwe. Ndipo m'malo mwake adaleredwa mnyumba
ya Farawo mpaka pamene adachoka ku Iguputo mothawa kupita
ku Madiyani ku Shamu. Kenako adabwera ali ndi mkazi wake
Binti Shuaibu (AS).
Ali m'njira kubwerera ku Iguputo, Mulungu adayankhula
naye. Ndipo adarrisankha kuti asenze Uthenga wa Mulungu.
Uthengawo adausenzadi. Ndipo pakati pa iye ndi Farawo ndi
amatsenga a Farawo padapezeka zopezeka mpaka Mulungu
adawamiza m'nyanja asirikali a Farawo pamodzi ndi iye mwini
Farawo pomwe Musa ndi ana a Isiraeli adapulumuka.
Kenako padapezeka nkhani zokhumudwitsa zomwe
zimachitika pakati pa Musa, Haruna ndi ana a Israeli, omwe
chikhalidwe chawo sichidali kufuna kugonjera Malamulo a
Mulungu, monga Karuna ndi ena ambiri onga iye.
Surat 28. Al-Qasas Juzu 20
817
t * sj£-l Y A jfi < / *j & \ 5j^»
Sural Al-Qasas XXVIII
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Td-Sin-Mim.
2. Izi ndi aya (ndime) za
m'buku (la Qur'an) Lofotokoza
(chilichonse chofunika pa Dini).
3. Tikukulakatulira (iwe
Mtumiki) nkhani Za Musa ndi
Farawo m'njira yoona kwa Anthu
okhulupirira. (Koma
osakhulupirira Sangapindule
kanthu ndi nkhanizi).
4. Ndithu, Farawo adadzikuza
padziko, ndipo Adawakhazika
(anthu a m'dzikolo)
M'magulumagulu; gulu lina la
mwa iwo Adalifooketsa (poliyesa
akapolo) ndi kupha Ana awo
achimuna, ndi kuwasiya a moyo
Ana awo achikazi. Ndithu, iye
adali Mmodzi wa oononga
kwambiri. 1
5. Ndipo tidafuna kuwachitira
zabwino amene Adafooketsedwa
padziko (la Iguputo), ndi
Kuwachita kukhala atsogoleri ndi
w.
ofa$\<£&\&\jr
-^
Farawo adauzidwa ndi mlosi kuti kudzabadwa mwana mwa Aisraeli
wamwamuna.yemwe adzathetsa ufumu wake. Pamene adamva izi adalamula
kuti makanda onse a amuna A Israeli aphedwe. Ghoncho ana amuna
ongobadwa kumene amaphedwa.
Surat 28. Al-Qasas Juzu 20
818
*j*- 1
V A jflrfeU 3jj-»
Kuwachitanso kukhala Amlowa
m'malo ( a Baiti Makadasi). 1
6. Ndi kuwapatsa mphamvu za
padziko (kuti Azichita mmene
angafunire) ndi kuti Timuonetse
Farawo ndi Hamana ndi magulu
Awo ankhondo, zomwe amaziwopa
(kuti Zingawathetsere ufumu wawo).
7. Ndipo tidamzindikiritsa mayi
wa Musa ( tinati), "Muyamwitse
(mwana wako), ndipo Ukamuopera
(chiwembu cha Farawo), Mponye
mumtsinje; usaope ndipo
Usadandaule ndithu Ife
tidzamubwezera Kwa iwe, ndipo
tidzamchita kukhala Mmodzi wa
Atumiki".
8. Choncho adamtola anthu A
Farawo kuti mapeto ake Adzakhale
m'dani kwa iwo ndi Odandaulitsa.
Ndithu, Farawo ndi Hamana ndi
magulu Awo ankhondo adali olakwa.
9. Ndipo mkazi wa Farawo
adati: "Musamuphe, akhale
chotsangalatsa diso Langa ndi
lako; usamuphe mwina
Angatithandize, kapena
tingam'chite kukhala Mwana
(wathu". Adanena izi) uku iwo
Asakudziwa (kuti adzakhala
m'dani wawo);
1 Chimene Mulungu wafuna chimachitika ngakhaie anthu atayesetsa m'njira
izi ndi izi kuti achizembe.
Surat 28. Al-Qasas Juzu 20
819
*>'
V A jfl , /i& \ 0jj~*
10. Ndipo mumtima mwa mayi
wa Musa Mudali mopanda kanthu
(mudalibe Maganizo ena koma
maganizo a Mwana wake).
Padatsala pang'ono Kuti aonetse
(chinsinsi cha mwanayo Ponena
kuti adali mwana wake),
Tikadapanda kulimbikitsa mtima
Wake, kuti akhale mmodzi mwa
Okhulupirira (lonjezo la Mulungu).
11. Ndipo (mayi wa Musayo)
adauza Mlongo wake (wa Musa),
"Mtsatire, (Komwe madzi akupita
naye)." Choncho iye
ankamuyang'ana Chapatali pomwe
iwo samadziwa (Za ichi).
12. Ndipo poyamba tidamuletsa
kuti Asayamwe kumawere a
woyamwitsa, (Kufikira pomwe
mlongo wake) adati: "Kodi
ndikusonyezeni eni nyumba Omwe
angakulerereni ndi kukhala Naye
momteteza bwino mwanayo?"
13. Choncho tidamubwezera
kwa mayi Wake kuti maso ake
atonthole, (Mtima wake
ukhazikike) ndi kuti Asadandaule;
ndi kuti adziwe kuti Lonjezo la
Mulungu ndi loona. Koma ambiri
a iwo sadziwa.
14. Ndipo (Musa) pamene
adakula Msinkhu wake ndi
kulingana bwino Tidampatsa nzeru
ndi maphunziro. Ndipo umo
riS '»» VCi '\<> >•> '1
Surat 28. Al-Qasas Juzu 20
820
•J*" 1
t A j tf. ^ 1 Ojj^
ndimomwe timalipirira Ochita
zabwino.
15. Ndipo (tsiku lina) adalowa
mumzinda Mozemba, eni
m'zindawo osadziwa. Ndipo
adapeza m'menemo anthu awiri
Akumenyana, mmodzi wochokera
kugulu Lake, ndipo winayo
wochokera kwa adani Ake. Tsono
wakugulu lake uja Adampempha
chithandizo pa mdani wake uja,
Ndipo Musa adammenya
chibagera mpaka Kumupha
(mdaniyo). Adanena: "Iyi
(Ndachitayi) ndintchito ya satana;
ndithu, lye ndimdani
wosokeretsa,woonekera."
16. Adati: "E, Mbuye wanga!
Ndithu Ndadzichitira zoipa
ndekha! Choncho
Ndikhululukireni!" Tero
(Mulungu) Adamkhululukira
(chifukwa sadalinge Kupha).
Ndithu, lye (Mulungu)
Ngokhululuka, Ngwachisoni.
17. Adati: "O, Mbuye wanga!
Chifukwa cha kuti mwandidalitsa,
sindidzakhala Mthangati wa oipa.
18. Choncho kudamuchera mu
mzindamo (m'mawa Mwake)uku
ali wodzazidwa ndi mantha
Akuyembekezera (kuti chiyani
chimpeze Pa zimene zidachitika)
pompo munthu uja Adampempha
&Jft$ fjp£*$tyy)$*
"■ -""Si
Surat 28. Al-Qasas Juzu 20
821
*>'
t A jA^fliil 9jj~i
dzulo chithandizo ankamuitana
(Kuti amthandize kumenyana ndi
m'dani wake Wina). Musa
adamuuza; ndithudi ndiwe
Wopotoka owonekera.
19. Choncho pamene adafuna
kumpanda, Yemwe ndi mdani wa
awiriwo, (uja Wofuna chithandizo
kwa Musa adaganiza Kuti Musa
afuna kuti ampande iye), Ndipo
adati: "E, iwe Musa! Kodi
Ukufuna kundipha monga momwe
Udaphera munthu uja dzulo? Iwe
sufuna China koma kukhala
wodzitukumula (Wankhanza)
padziko, ndipo sukufuna Kukhala
mmodzi mwa ochita zabwino
(Oyanjanitsa okangana ndi
kukonza zinthu).
20. (Farawo zitamfika
mphekesera kuti Musa wapha
munthu pothangata mu Israeli,
adalamula kuti Musa paliponse
Pomwe angapezeke, agwidwe ndi
Kuphedwa ). Choncho munthu
adadza Akuthamanga kuchokera
kumalekezero A m'zindawo.
Adati: "E, iwe Musa! Akuluakulu
akuchita upo kuti akuphe Choncho
choka (m'dziko muno); Ndithu,
ine ndine mmodzi mwa okufunira
Iwe zabwino,
21. Ndipo adachoka
mumzindawo ali woopa Uku
akuyembekezera (kumpeza choipa
Si*
> •«• m. ' '\\^9 *Sl'C'M \' m \" "<"*
Siirat 28. Al-Qasas Juzu 20
822
*>i
X A u fi. s i&\ 5jj-»
Kuchokera kwa adani ake). Adati:
"E, Mbuye wanga! ndipulumutseni
Kwa anthu ochita zoipa".
22. Ndipo pamene adalunjika
(kumka) ku Madiyani adati:
"Mwina Mbuye Wanga
andiongolera kunjira yoyenera."
23. Ndipo pamene adawafika
madzi a ku Madiyani (pomwe
anthu kumeneko Ankatungapo
madzi), adapeza gulu La anthu
likumwetsa (ziweto zawo), Ndipo
pambali (pagululo) adapeza akazi
Awiri akuletsa (ziweto zawo kuti
Zisapite kukamwa ndi ziweto
zinazo). (Musa) adati "Kodi
mwatani? (Bwanji
Simukuzimwetsa ziweto zanu?)
Iwo Adati: "Sitingamwetse (ziweto
zathu) Mpaka abusa atachotsa
(ziweto zawo, Chifukwa sitingathe
kulimbana nawo). Ndipo bambo
wathu ndinkhalamba Yaikulu
kwabasi."
24. Choncho (Musa)
adawamwetsera (ziweto Zawo);
kenako adapita Pamthunzi, ndipo
adati: "O, Mbuye wanga! Ndithu,
Ine ndiwosaukira chabwino
chimene Munditsitsire."
25. Kenako mmodzi mwa
asungwana aja Adadza kwa iye
uku akuyenda mwamanyazi.
(Msungwanayo) adati: "Ndithu
&JS&3&
\J* I £-*U 6&$ &JX* 'X* *J5 WJ
<&4
Surat 28. Al-Qasas Juzu 20
823
*>-i
t A jfl < fl ' d \ 0jj-*»
tate Wanga akukuitana kuti
akakupatse malipiro
Pakutimwetsera (ziweto zathu)."
Choncho Pamene adamdzera,
(mneneri Shuaibu)
Ndikumulongosolera nkhani adati:
"Usaope; Wapulumuka kwa anthu
oipa."
26. Mmodzi wa iwo
(asungwana aja) adanena: "E,
bambo wanga mulembeni ntchito
(Kuti akhale woweta ziweto
m'malo Mwa ife). Ndithu amene
alibwino kuti Mumulembe ntchito
ndi yemwe ali wa-Mphamvu
wokhulupirika (zonse ziwiri Mwa
iyeyu zirimo.)
27. (Shuaibu) adati (kwa iye):
"Ine Ndikufuna kukukwatitsa
mmodzi mwa Asungwana anga
awiriwa, chiongo chake
Ndikundigwirira ntchito zaka
zisanu ndi Zitatu; ngati
utakwaniritsa zaka khumi ndiye
Kuti nkufuna kwako. Sindikufuna
kukuvutitsa (Pokuchulukitsira
zaka); undipeza, Mulungu
Akafuna, kuti ndine mmodzi wa
anthu abwino, (Wokwaniritsa
lonjezo)."
28. (Musa) adati: "Zimene
mwandilonjezazi Zili pakati pa ine
ndi inu. Nyengo iriyonse imene
ndikwaniritse Pa ziwirizi (pogwira
ntchitoyo, ndiye Kuti
®t&&
Surat 28. Al-Qasas Juzu 20
824
Y ♦ s-ji-1 Y A j^-Aflii Oj^t
ndakwaniritsa lonjezo lanu)
Musandichitire mtopola. Ndipo
Mulungu Ndiye muyang'aniri pa
zomwe tikukambazi.
29. Musa pamene adakwaniritsa
nyengoyo, adanyamuka ndi banja
lake (kubwerera Kwao) adaona
moto kumbali ya phiri. Adauza
banja lake: "Dikirani ndithudi ine
Ndaona moto mwina mwake
Ndingakutengereni nkhani za
kumeneko Kapena chikuni cha
moto kuti muothe".
30. Tsono pamene adaudzera,
adaitanidwa Kuchokera mbali ya
kumanja ya Chigwacho, pa malo
wodalitsidwa Kuchokera mu
mtengo ankati: "E, Iwe Musa
ndithudi Ine ndi Mulungu Mbuye
wazolengedwa."
31. Ndipo ponya (pansi) ndodo
yakoyo! Choncho pamene
adayiona Ikugwedezeka monga
kuti iyo Ndi njoka, adatembenuka
kuthawa Ndipo sadachewuke.
(Adauzidwa): "E, iwe Musa!
Bwera kuno, usaope. Ndithu, Iwe
ndiwe mmodzi wokhala ndi
mtendere.
32. Lowetsa mkono wako
m'thumba mwako (Palisani la
mkanjo wako), utuluka Uli
woyera, popanda choipa. Ukachita
Mantha, fumbata dzanja Lako
Surat 28. AI-Qasas Juzu 20
825
*>'
YA ^/^fliJt °JJ-**
chakukhwapa; (ukatero Mantha
akuchokera). Izi zidzakhala
Zizindikiro ziwiri zochokera Kwa
Mbuye wako kwa Farawo ndi
nduna Zake. Ndithu, iwo ndianthu
olakwa".
33. (Musa) adanena (Moopa)
"E, Mbuye Wanga! Ine ndidapha
munthu mwa iwo, Ndipo ndikuopa
kuti akandipha.
34. Ndipo m'bale wanga
(Haaruni) Ndikatswiri
pakuyankhula kuposa ine.
Mutumizeni pamodzi ndi ine
monga Mnthandizi,
azikandivomereza (pazimene
Ndizikanena). Ndithu, ine
ndikuopa Kuti akanditsutsa."
35. (Mulungu) adati:
"Tilimbitsa dzanja Lako ndi mbale
wakoyo ndipo tikupatsani
Kupambana, iwo sangafikitse
masautso Pa inu; chifukwa cha
zozizwitsa Zathuzo. Inu awiri
ndiamene akutsatireni, ndinu
Opambana."
36. Pamene Musa adawadzera
ndi zizindikiro Zathu zoonekera
poyera, adati: "Ichi sichina Koma
ndi matsenga wopeka; sitidamvepo
Zimenezi kumakolo athu akale."
37. Ndipo Musa adanena:
"Mbuye wanga Akumudziwa
yemwe wadza ndi chiongoko
©t&>©Gfci*^<3E2
Surat 28. Al-Qasas Juzu 20 826 *• *jk* t A j^^\ oj^
Kuchokera kwa lye ndi yemwe
adzakhala Ndi mathero a pokhala
pabwino. Ndithu,ochita zoipa
sakapambana".
38. Ndipo Farawo adati: "E, inu
nduna (Zanga)! Sindidziwa kuti
inu muli ndi Mulungu (wina)
kupatula ine. Choncho, Iwe
Haamana! Ndiwotchere njerwa
Ndiye undimangire chipilala kuti
mwina Mwake ndingamsuzumire
Mulungu wa Musa.Ndithu, Ine
ndikumganizira kuti Ndi mmodzi
wa abodza".
39. Ndipo iye pamodzi ndi
makamu ake Ankhondo
adadzitukumula padziko Popanda
chilungamo ndipo ankaganiza Kuti
iwo sadzabwezedwa kwa Ife.
40. Koma tidamulanga ndi
magulu ake ankhondo Ndi
kuwaponya m'nyanja; yang'ana,
kodi Adali bwanji mathero aochita
zoipa.
41. Ndipo tidawachita kukhala
atsogoleri Oitanira (anthu)
kumoto; ndipo tsiku Lachiweruzo
(Kiyama) sadzathandizidwa.
42. Tidawatsatiziranso
matemberero padziko lino Lapansi.
Ndipo tsiku la chimaliziro iwo
Adzakhala oyipitsitsa (ndi
kuthamangitsidwa Ku chifundo
cha Mulungu).
%#^<J^I&\
Surat 28. Al-Qasas Juzu 20
827
,>»
T A j^-Aflil 5 jj--
43. Ndipo ndithu, Musa
tidampatsa Buku Pambuyo
powononga mibadwo yoyamba
Kuti likhale chiphanulamaso cha
anthu (kuti Liwaunikire kunjira
yolungama), ndi kuti Likhale
chiongoko ndi chifundo kuti Iwo
akumbukire.
44. Ndipo iwe sudali mbali
yakuzambwe (Kwa phiri limenelo)
pamene tidampatsa Musa lamulo;
sudalinso mwa amene Adalipo
(pamalopo).
45. Koma ife tidaumba
mibadwo yambiri (Pambuyo pa
Mneneri Musa) kotero kuti Zaka
zidapitapo zambiri pakati pawo.
Ndipo sudakhale nawo anthu a
Madiyani Ndi kumawawerengera
aya (ndime) Zathu; Koma ife tidali
kutuma (atumiki ndi
Kuwafotokozera zomwe zidachitika
Patsogolo ndi pambuyo pawo,
monga Momwe takutumira iwe ndi
kukudziwitsa Nkhani zakale ndi
zimene zikudza Pambuyo).
46. Ndipo sudali kumbali kwa
phiri la Turi pamene tidamuitana
(Mneneri Musa). Koma
(kutumidwa kwako) Ndimtendere
wochokera kwa Mbuye wako Kuti
uwachenjeze anthu omwe
mchenjezi Sadawadzere (mnthawi
yaitali) iwe usadadze, Kuti
akumbukire.
•^
Surat 28. Al-Qasas Juzu 20
828
*>'
T A jfl'AJh Ojj-^
47. (Ndipo sitikadatuma) koma
kuti mavuto Akawapeza ochokera
(kuzoipa) zomwe Atsogoza manja
awo, amanena: "Mbuye Wathu!
Bwanji wosatitumizira Mtumiki
kuti titsate mawu Anu ndi kukhala
mwa Okhulupirira".
48. Koma choona pamene
chidawadzera Kuchokera kwa Ife,
adati: "Bwanji Sadapatsidwe
monga zomwe Adapatsidwa
Musa? (Monga Kutembenuza
ndodo kukhala njoka, ndi zina
Zotero)" Kodi kalelo sadazikane
zomwe Adapatsidwa Musa?
Nkunena (za Taurati Ndi Qur'an):
"Ndi matsenga awiri amene
Akuthandizana." Ndipo adati:
"Ndithu, Ife tikuwakana onse."
49. Nena: "Bwerani nalo Buku
lochokera Kwa Mulungu lomwe
lili ndi chiongoko Chabwino
kuposa awiriwa: (Taurati ya
Mneneri Musa, ndi iyi Qur'an),
kuti Ndilitsate ngati inu mukunena
zoona."
50. Koma ngati sadakuyankhe,
dziwa kuti Akutsatira zilakolako
zawo. Kodi Ndani wasokera
kwambiri kuposa yemwe
Akutsatira zilakolako zake
popanda Chiongoko chochokera
kwa Mulungu? Ndithu, Mulungu
saongola anthu Odzichitira zoipa.
Surat 28. Al-Qasas Juzu 20
829
t • *j£-l T A ^./iiil 5jj-»»
51. Ndipo ndithu, tafikitsa
mawu kwa iwo Mochulukitsa,
mwatsatanetsatane Kuti iwo
akumbukire.
52. Amene tidawapatsa Buku
kale ili Lisadadze , akulikhulupirira
ili (Buku la Qur'an).
53. Ndipo likawerengedwa kwa
iwo, akuti: "Talikhulupirira;
ndithu, ichi nchoona Chochokera
kwa Mbuye wathu; ndithu, Ilo
lisanadze ife tidali ogonjera
(Mulungu)
54. Iwo adzapatsidwa malipiro
awo kawiri (Chifukwa chotsatira
Mneneri Musa Ndi Mneneri Isa,
kale; ndipo tsopano Ndikumtsatira
Mneneri Muhammad {SAW})
Nchifukwa chakuti adapirira;
amachotsa Choipa (pochita)
chabwino, ndipo M'zimene
tawapatsa akupereka chopereka
(Sadaka).
55. Ndipo akamva zopanda pake
amazipewa, ndipo Amati (kwa
achibwanawo): "Ife tili ndi Zochita
zathu inunso muli ndi zochita
zanu, Mtendere ukhale painu. Ife
sitifuna (kutsutsana) Ndi mbuli."
56. Ndithu, iwe sungathe
kumuongola amene Ukumfuna,
koma Mulungu amuongola Amene
wamfuna. Ndipo lye akudziwa Za
amene ali oongoka.
&\' 9 *<"•■'
te£$&Q$}^<£$
*&&
^«&^\sj)^^
<&
^^*<0^f^^0<^f
Surat 28. Al-Qasas Juzu 20
830
,j*
T A jn yii . l t djj-a
57. Ndipo akunena (akafiri a m'
Makka, kuuza Mtumiki):"Ngati
titsatira chiongoko (ichi Chimene
wadza nacho) pamodzi ndi iwe,
Tifwambidwa m'dziko lathu
(potimenya Nkhondo mafuko ena a
Arabu)."Kodi Sitidawakhazike
pamalo opatulika ndi Pamtendere
pomwe zipatso Zamitundumitundu
zikudza pamenepo Mwaulere
(monga riziki) zochokera kwa Ife?
Koma ambiri a iwo sadziwa.
58. Kodi ndimidzi ingati imene
tidaiononga Yomwe inkanyadira
za moyo wawo (Wosavutika ndi
wodya bwino)! Umo M'malo
mwawo simudakhalidwebe
Pambuyo pawo koma mochepa
basi; Ndipo ife tidalowa chokolo
m'zimenezi.
59. Ndipo Mbuye wako sali
owononga midzi Pokhapokha
akatuma Mtumiki mumzinda
wawo Waukulu ndi
kuwawerengera mawu a m'ndime
Zathu, (akakana ndi pamene
timawaononga); Ndiponso sitili
owononga midzi pokhapokha
Anthu ake atakhala achinyengo.
60. Ndipo chilichonse chimene
mwapatsidwa Nchosangalatsa
chamoyo wapadziko Ndiponso
chokometsera chake (chomwe
Sichikhalira kutha); koma chomwe
chili Kwa Mulungu ndicho
§$&$?
Surat 28. Al-Qasas Juzu 20 831 t* *jJh YA j^-aaJi *jj~>
chabwino, Chamuyaya; kodi
bwanji simukuzindikira?
61. Kodi munthu yemwe
tamulonjeza lonjezo Labwino (kuti
akalowa ku munda Wamtendere)
kotero kuti iye akakumana Nalo
(lonjezolo), angafanane ndi yemwe
Tamsangalatsa ndi zosangalatsa
zamoyo Wapadziko basi, kenako
iye nkukhala Mmodzi
okaponyedwa (kumoto) tsiku La
chiweruzo (Kiyama)?"
62. Ndipo (akumbutse) tsiku
limene (Mulungu) Adzawaitana,
adzati: "Ali kuti anzanga Aja
omwe mumanena (kuti
ndianzanga)?
63. Adzanena amene mawu
(onena zachilango) Atsimikizika
pa iwo: "Mbuye Wathu! Awa
ndiamene tidawasokeretsa;
Tidawasokeretsa monga momwe
Tidasokerera tikudzipatula Ndi
iwo kwa inu; Samatilambira ife".
64. Ndipo kudzanenedwa:
"Itanani aphatikizi Anu;" Choncho
adzawaitana koma
Sadzawayankha.Ndipo azawawona
mavuto (Pa nthawiyo azakhumba)
akadakhala Oongoka (padziko
lapansi kotero kuti Akadapeza
mtendere pa tsiku La chimaliziro).
65. Ndipo (akumbutse) tsiku
limene adzawaitana Nkudzati:
©,
-..w^jb
Surat 28. Al-Qasas Juzu 20
832
V • *-j£-1 T A ^n^aS s 5jj--
"Kodi mudawayankha chiyani
Atumiki?"
66. Basi tsiku limenelo nkhani
zidzawasowa Choncho iwo
sadzatha kufunsana.
67. Koma amene walapa ndi
kukhulupirira ndi Kuchita ntchito
zabwino, adzakhala Mwa
opambana?
68. Ndipo Mbuye wako
amalenga chimene wafuna Ndi
kuchisankha (chimene wafuna).
Iwo alibe chifuniro. Mulungu
Wapatukana ndi zonse zochepetsa
ulemerero Wake, ndipo watukuka
ku zomwe Akumphatikiza nazo.
69. Ndiponso Mbuye wako
akudziwa zimene Zifuwa zawo
zikubisa (maganizo awo) ndi
Zimene akuwonetsera (poyera).
70. Ndipo lye ndi Mulungu;
palibe Wopembedzedwa
m'choonadi koma lye.
Kuyamikidwa konse (kwabwino)
pachiyambi Ndi kumapeto
nkwake; ndipo kulamulanso
Nkwake, ndipo inu
mudzabwezedwa kwa lye.
71. Nena: "Tandiuzani ngati
Mulungu Atakupangirani usiku
kuti usachoke Mpaka tsiku la
chiweruzo (Kiyama), Kodi
ndimulungu wanji osati Mulungu
» J "\i$v&&z
j^jy^oi.
®v$$Z
Surat 28. Al-Qasas Juzu 20
833
Y » tj)r\ Y A j jfl^fll l 5 jj--
Amene angakudzetsereni kuunika?
Kodi Simumva?"
72. Nena: "Tandiuzani ngati
Mulungu ataupanga Usana kuti
usachoke mpaka tsiku la
Chiweruzo (Kiyama), Kodi ndi
mulungu wanji Osati Mulungu
amene angakudzetsereni Usiku
m'mene mumapumulamo? Kodi
simuona (chifundo cha Mulungu)?
73. Ndipo mu chifundo Chake,
Adakupangirani usiku ndi usana
kuti Muzipumulamo ndi
Kufunafuna zabwino Zake
(masana) kuti muthokoze.
74. Ndipo tsiku limene
(Mulungu) adzawaitana Adzati:
"Ali kuti anzanga aja amene
Mumati ndimilungu inzanga?"
75. Ndipo mumpingo uliwonse
tidzatulutsa Mboni (yawo
yowaikira umboni), ndipo
Tidzawauza: "Bwerani ndi umboni
wanu". Pamenepo adzadziwa kuti
choonadi ncha Mulungu, ndipo
zidzawasowa zimene Amapeka
76. Ndithu,Karuni adali mwa
anthu a Musa; Koma adazikweza
kwa iwo,ndipo tidampatsa
Nkhokwe za chuma zomwe makiyi
ake Ngolemetsa kagulu ka anthu
anyonga (Kuwasenza). Anthu ake
adamuuza: "Usanyade; ndithu,
Mulungu sakonda Onyada.
X£?2
Siirat 28. Al-Qasas Juzu 20 I 834 Y * ^j*-i Y A ja^Ji 5jj^
77. Ndipo funafuna, kupyolera
m'zomwe Mulungu wakupatsa,
nyumba yabwino Yomaliza,
usaiwale gawo lako la m'dziko;
Chita zabwino monga momwe
Mulungu Wakuchitira zabwino,
ndipo usafune Kuononga padziko;
ndithu, Mulungu sakonda
Oononga."
78. Adati: "Ndithu, ndapatsidwa
izi chifukwa Cha kudziwa kwanga
komwe ndili nako" Kodi iye
sadadziwe kuti Mulungu
Adawaononga anthu patsogolo
pake omwe Adali anyonga
kwambiri kuposa iye, Komanso
osonkhanitsa chuma chambiri
Ndipo oipa sadzafunsidwa
zolakwa zawo. (Mulungu
akudziwa zonse za iwo)!
79. Choncho, adatulukira kwa
anthu ake (Monyada) uku
atadzikongoletsa. Amene Akufuna
moyo wapadziko adanene
(Mokhumbira): "Kalangaife!
Tikadapatsidwa Monga
wapatsidwa Karuna! Ndithu, Iye
ngodala kwakukulu."
80. Ndipo amene adapatsidwa
kuzindikira Adanena: "Tsoka lanu!
Malipiro a Mulungu ngabwino
kwa yemwe Wakhulupirira ndi
kuchita zabwino, (Kuposa izi ali
nazo Karuni); ndipo
b
Surat 28. Al-Qasas Juzu 20
835
,>>
Y A u a-4&\ o jj-*>
Sadzapatsidwa zimenezi koma
okhawo Ali opirira."
81. Kenako tidamdidimiza
m'nthaka iye ndi Nyumba yake;
ndipo adalibe gulu Lililonse
lomuthangata popikisana ndi
Mulungu, ndipo sadali
mwaodzipulumutsa Okha.
82. Ndipo ankanena amene
ankalakalaka Ulemerero wake
dzulo: " E, zoonadi Mulungu
amamuonjezera chuma amene
Akumfuna mwa akapolo Ake
(Chingakhale Ali oipa
wosayanjidwa ndi Iye) ndipo
Amamuchepetsera chuma (amene
wamfuna Kotero ngakhale ali
woyanjidwa ndi Iye.) Pakadapanda
Mulungu kutimvera chisoni,
(Mkukhumbira kwathu pazimene
adampatsa Karuni)akadatikwirira
m'nthaka. Ha! Zoonadi
Osakhulupirira Mulungu
sangapambane".
83. Nyumba yomalizirayo
tikawapangira amene Sakufuna
kuzikweza pa dziko ndi kuononga.
Ndipo malekezero abwino adzakhala
A wanthu owopa Mulungu.
84. Amene achite chabwino,
adzapeza mphoto Yoposa chimene
adachitacho ndipo amene Achite
choipa sadzalipidwa (china chake)
Koma zoipa zomwezo zimene
Adali kuzichita.
®&t£&\<'^\
ei&JSfctfSj
Surat 28. Al-Qasas Juzu 20 836
*J*-»
Y A j^uaiJI 5j^»
85. Ndithudi yemwe
wakulamula kuitsata Qur'an,
mwachoonadi adzakubwezera Pa
malo pobwerera. Nena! "Mbuye
Wanga ndi yemwe akudziwa
amene Wadza ndi chiongoko ndi
yemwe Ali m'kusokera koonekera
poyera".
86. Ndipo iwe sudali kulakalaka
kuti Ungapatsidwe Buku (pamodzi
ndi uneneri) Koma izi zidachitika
pa chifundo chochokera Kwa
Mbuye wako; choncho usakhale
M'thandizi wa anthu
osakhulupirira (Mulungu).
87. Ndipo asakutsekereze
kutsatira ndime za (Mawu a)
Mulungu pa mbuyo
povumbulutsidwa Pa iwe aitanire
anthu kwa Mbuye wako, Komatu
usakhale m'gulu la anthu
Omphatikiza Mulungu ndi mafano
88. Ndipo usapemphe mulungu
wina pa modzi Ndi Mulungu.
Palibe wopembedzedwa
Mwachoonadi koma lye yekha.
Chinthu Chilichonse
chidzaonongeka kupatula Nkhope
yake. Ulamuliro (wazinthu zonse)
Uli kwa lye ndipo kwa lye ndi
kumene Mudzabwerera nonsenu.
Surat29.Al-'Ankabut Juzu20
837
r * *j*-l 1 S Cj^jj6\ Ojj~-
Sura iyi idavumbulutsidwa ku Makka. Aya zake zilipo 69.
Aya 1 mpaka 11 zidavumbulutsidwa ku Madina. Surayi
yayamba ndi kufotokoza kuti nkofunika kwa okhulupirira
kuyesedwa mayeso ndi masautso, monga nkhondo, kuti
chikhulupiriro chawo chikhale chokhwima. Ndipo yalangiza
munthu kuti achitire zabwino makolo ake ndi kuchita jihadi
(nkhondo) panjira ya Chauta. Ndiponso yafotokoza za kusiyana
chikhulupiriro kwa anthu. Ena mwa iwo akungonena chabe kuti
akhulupirira pomwe mitima yawo siinakhulupirire.
Surayi yafotokozanso za Mneneri Nuhu ndi khama lake
poitanira anthu ake kunjira ya Mulungu. Ndipo yafotokozanso
nkhani ya Luti ndi machitidwe a anthu ake ndi kutsitsidwa kwa
angelo odzawaononga pa chionongeko chomwe iye ndi mbumba
yake adapulumuka kupatula mkazi wake.
M' surayi mukunenedwanso nkhani ya Shuaibu ku Madiyani,
ndi nkhani ya Hudu ndi Adi, Swaleh ndi Samudi. Ndipo surayi
yafotokozanso za kunyengedwa kwa Kaaruna, Farawo ndi
Haamana ndi malekezero azochita zawo. Kenaka yafotokoza
kuti mapemphero a Amushirikina maziko ake ngofooka kuposa
nemba (nyumba ya kangaude). Ndipo yati mafanizo amenewa
akuzindikiridwa ndi okhawo omwe ali ndi nzeru zakuya. Kenako
Mulungu walamula Mneneri wake kuti asatsutsane ndi eni
mabuku koma kupyolera m'njira yabwino. Ndipo wafotokozanso
kuti Mtumiki Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale naye)
adali wosadziwa kulemba ndi kuwerenga. Ikutinso, kusadziwa
kulemba ndi kuwerenga kukusonyeza kuona kwa uthenga wake.
Ndipo Chauta wafotokozanso za liuma la Amshirikina pakufuna
kwawo zozizwitsa zimene atha kuzikana zikapezeka, monga
momwe anthu a Musa adazikanira. Mulungu m' surayi
wafotokozanso za malipiro a otsutsa, pa tsiku la chimaliziro.
Ndipo wafotokozanso za moyo watsiku la chimaliziro. Mulungu
wafotokoza kuti Amushirikina akakhala pamavuto amapempha
chauta. Koma akakhala pamtendere amamukana Mulungu.
Kenako walongosola za mtendere umene adawadalitsa nawo
eni mzinda wa Makka, koma chikhalirecho iwo samuthokoza.
Komanso walimbikitsa zakuchita jihadi (nkhondo) panjira Yake.
Surat29.AI-'Ankabut Juzu20
838
t • *j£-l t ^ OjXaJl ijj^p
SuratAl-'AnkabutXXIX
. jtz?3?S-.sjw-a. ^-^_/,
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1 . v4 lif-Ldm-Mim .
2. Kodi anthu akuganiza kuti
azasiyidwa Popanda kuyesedwa
ndi masautso pakungonena Kuti:
"Takhulupirira?" (Iyayi, ayenera
Kuyesedwa ndithu, ndi masautso
Osiyanasiyana pamatupi pawo ndi
pachuma Chawo kuti adziwike
woona ndi Wachiphamaso).
3. Ndipo ndithu, tidawayesa
amene adalipo Patsogolo pawo.
Ndithu, Mulungu awaonetsera
Poyera amene ali olankhula zoona,
Ndithu, Mulungu awaonetsera
Poyera amene ali olankhula
zabodza.
4. Kodi amene akuchita zoipa
akuganiza Kuti atipambana (kotero
kuti Sitingawalange)?
Ndichiweruzo Choipa chimene
akuweruzacho.
5. Amene akuyembekezera
kukumana ndi Mulungu,(agwire
ntchito yabwino pamoyo Wake
kuti akakumane naye ndi
zabwino). Ndithu, nthawi ya
Mulungu (tsiku la Chimaliziro)
idza (popanda chikaiko). Ndipo
lye Ngwakumva (zonena za
^rn&tiw
ofa&^^j
-^
Surat29.Al-'Ankabut Juzu 20
839
Y • *j£-t T ^ Oj-SoOi djj~>
akapolo Ake), Ngodziwa
(zachinsinsi chawo). 1
6. Ndipo amene akuchita khama
(polimbana ndi Akafiri, kapena
pogonjetsa mtima wake Kuti
utsatire malamulo a Mulungu),
Ndithu, zabwino za khamalo zili
pa iye Mwini. Ndithu, Mulungu
siwosaukira Chilichonse kwa
zolengedwa Zake.
7. Ndipo amene akhulupirira
Ndi kumachita zabwino,
Tidzawafafanizira zoipa zawo,
ndipo Tidzawalipira zabwino
kuposa zomwe Amachita.
8. Ndipo tamulamula munthu
kuchitira zabwino Makolo ake.
Koma ngati atakukakamiza
(Makolo ako) kuti undiphatikize
Ine Ndi (zinthu zina) zomwe iwe
sukuzidziwa, Usawamvere. Kwa
ine ndiko kobwerera Kwanu, ndipo
ndidzakuuzani zimene Mumachita.
9. Ndipo amene akhulupirira
ndi kumachita Zabwino,
tidzawalowetsa m'gulu la anthu
Abwino.
gta^&^JLPVf 6^&J
Gtt.ltft 'cAi**' 1
1 Tanthauzo la ndimeyi nkuti amene akuyembekezera kuti akalandire malipiro
abwino kwa Mulungu, apirire pamoyo wapadziko lapansi polimbika kumvera
Mulungu mpaka adzakumane ndi Mulungu. Ndithudi, kukumana ndi Mulungu
kuli pafupi.
2 Ngati makolo onse awiri atalimbikira ndi mphamvu zawo zonse kuti iwe
umukane Mulungu, kapena kuti umuphatikize ndi chinthu china chomwe
nchosayenera kukhala Mulungu, usawamvere pazimenezo, chifukwa chakuti
palibe kugonjera cholengedwa polakwira Mlengi.
Surat29.Al-'Ankabut Juzu20
840
t ♦ ^j£-» Y ^ O^lyJl fljj-**
10. Ndipo alipo ena mwa anthu
omwe akunena, "Takhulupirira
mwa Mulungu". Koma
Akavutitsidwa chifukwa cha
Mulungu, Amawachita masautso a
anthu monga Chilango cha
Mulungu, (sapirira; Iwowa ndi
achinyengo (Amunafikina). Ndipo
chikadza chipulumutso chochokera
Kwa Mbuye wako amanena:
"Ndithu, ife Tidali pamodzi ndi
inu" (Koma Chikhalirecho
akunena zonama). Kodi Mulungu
sadziwa zomwe zili m'zifuwa Za
zolengedwa? 1
11. Ndipo ndithu, Mulungu
awaonetsera Poyera amene
akhulupirira (moona), Ndiponso
awaonetsera poyera Amunafikina
(achinyengo).
12. Ndipo amene
sadakhulupirire adanena kwa
Okhulupirira: "Tsatani njirayathu;
(Musatsate njira ya Muhammad).
Ife Tidzakusenzerani machimo anu
(kuti Chilichonse chisakupezeni).
Koma Sadzasenza chilichonse cha
machimo Awo, ndithu, iwo
ngabodza.
* ■<'-lS\ft3 h ,
*""7j
*h;jt 9 '-w-**-<
Alipo ena pakati pa anthu amene amangonena ndi malirime awo okha kuti:
"Takhulupirira Mulungu". Koma mmodzi wawo akavutitsidwa chifukwa cha
chikhulupiriro chakecho, amatuluka m'chipembedzomo. Ndipo masautso a
anthu amati ndicho chifukwa chomwe chidawachotsetsa m'chipembedzocho.
Komatu chilango cha Mulungu nchosafanana ndi chilango cha anthu.
Chofunika kwa iwo nkupirira ndi kulimba mtima; osatekeseka ndi chilichonse
ngakhale choononga moyo wawo.
Siirat 29. A1-' Ankabut Juzu 20
841
V » tj)r\ V ^ 0^£yJl Sjj-j
13. Ndipo ndithudi, adzasenza
mitolo ya machimo Ndi mitolo
yina yamachimo (ya omwe
Adawasokeretsa) poiphatikiza
kumitolo Yawo ya machimo.
(Nawonso osokezedwa,
Adzasenzanso mitolo ya machimo
chifukwa Cha kutsatira kwawo
anthu owasokezawo). Ndipo pa
tsiku la Kiyama (chimaliziro,)
Ndithu, adzafunsidwa pa zimene
amapeka.
14. Ndipo ndithu, tidamtuma
Nuhi kwa anthu Ake ndipo
adakhala nawo zaka chikwi
Chimodzi kupatulapo zaka
makumi Asanu. (Koma m'nthawi
yonseyi sadatsatire Ulaliki wake).
Choncho chigumula Chidawapeza.
(Ndipo adamira onse), Uku ali
odzichitira zoipa. ]
15. Tidampulumutsa iye (ndi
anthu ake) A m'chombo; ndipo
tidachita ichi kuti Likhale phunziro
kwa zolengedwa.
16. Ndipo (akumbutse nkhani
ya) Ibrahim Pamene adawauza
anthu ake: "Mpembedzeni
Mulungu ndi kumuopa. Zimenezo
'»KtL
1 M'ndime iyi, Mulungu akumthondoza Mtumiki Wake, Muhammad (madalitso
ndi mtendere zikhale naye) pomufotokozera kuti kusakhulupirira kwa anthu
akowa sichinthu chachilendo. Nawonso amene adalipo kale adamtsutsa Nuhi
ngakhale kuti adalalikira kwa nthawi yayitali mpaka chigumula chidawamiza
onse. Nawonso anthu akowa aonongedwa monga momwe zidalili ndi anthu a
Nuhi. Choncho usatekeseke ndi kusakhulupirira kwawo.
Surat 29. Al-< Ankabut Juzu 20
842
Y • tji-l Y ^ O^XjJi 5jj~-
Nzabwino kwa inu ngati
mukudziwa (Kusiyana kwa
chabwino ndi choipa).
17. Ndithu, inu mukupembedza
mafano Kusiya (kupembedza)
Mulungu ndipo Mwadzipangira
chonama. Ndithu, Amene
mukuwapembedzawo kusiya
Mulungu, sangakupatseni riziki
(madalitso) Funani riziki
(madalitso) Kwa Mulungu, ndipo
mpembedzeni lye Yekha ndi
kumthokoza. Kwa lye ndikomwe
Mudzabwezedwa (tsiku la
chimaliziro).
18. Ndipo ngati mutsutsa,
ndithu, mibadwo Ya omwe adalipo
patsogolo panu Idatsutsanso;"
ndipo kwa Mtumiki Kulibe udindo
wina koma Kufikitsa uthenga
woonekera Poyera, (womveka
bwino).
19. Kodi saona momwe
Mulungu ayambitsira Zolengedwa.
Kenako nkuzibwerezanso. Ndithu,
kwa Mulungu zimenezo Nzosavuta.
20. Nena: "Yendani padziko ndi
kuona momwe Mulungu
adayambitsira chilengedwe;
Kenako Mulungu adzaumba,
kuumba Kwina.Ndithu, Mulungu
Ndiwokhoza chilichonse.
21. Amamlanga yemwe
wamfuna ndipo Amamchitira
,1| 99 9 * 9 999* * 9 €i
*'A4XS&#SB&&
Surat 29. AI-' Ankabut Juzu 20
843
t » *j£-l t ^ Oj-£ydl 5jj-»
chifundo amene wamfuna Ndipo
kwa lye nonse mudzabwezedwa
22. Ndipo inu
simungampambane (Mulungu)
Padziko ngakhale kumwamba
(pomuzemba Kuti asakulangeni).
Inu mulibe mtetezi Kapena
mpulumutsi kupatula Mulungu".
23. Ndipo amene akana aya
(ndime) za Mulungu Ndi
kukumana Naye amenewo ndiwo
ataya Mtima pa zakupeza chifundo
Changa, ndipo Iwowo ndiwo
adzapeza chilango Chowawa.
24. Choncho yankho la anthu
ake silidali lina Koma adangoti:
"Mupheni kapena mtentheni Ndi
moto". Koma Mulungu
adampulumutsa Kumoto. Ndithu,
m'zimenezi muli Malingalilo
(osonyeza mphamvu za Mulungu)
kwa anthu okhulupirira.
25. Ndipo adanena: "Ndithu,
inu mwasankha Mafano kukhala
milungu kusiya Mulungu
Weniweni, ndipo mukukondana
pakati panu M'moyo wapadziko;
(pokhalirana Pamodzi ndi
kupitiriza kupembedza Mafanowo
mwachimvano). KomatsikuLa
Kiyama (chiweruzo),
mudzakanana Wina ndi mnzake
ndiponso Mudzatembererana Wina
ndi mnzake malo anu adzakhala
«$»W£
Surat 29. Al-'Ankabiit Juzu 20
844
Y • *jA-l Y S o^ScaJi Ojj--
Kumoto, ndipo simudzapeza
Okupulumutsani
26. Choncho (Mneneri) Luti
adamkhulupirira. Ndipo (Mneneri
Ibrahim) adanena: "Ndithu, Ine
ndikusamukira (kudziko lomwe)
Mbuye Wanga (wandilamulira).
Ndithu, lye Ngwamphamvu
zoposa Ngwanzeru zakuya."
27. Ndipo tidampatsa (Mneneri
Ibrahim) Isihaka ndi Yakubu,
ndipo Tidaika uneneri ndi Buku pa
mbumba yake, Ndipo tidampatsa
malipiro ake padziko Lapansi;
ndithu iye pa tsiku la chimaliziro
Adzakhala mwa anthu abwino. 1
28. Ndipo (akumbutse nkhani
ya Mneneri) Luti pamene
adawauza anthu ake: "Ndithu, inu
mukuchita zadama; palibe Amene
adakutsogolerani kuzichita
(Zadamazo) mwa zolengedwa.
29. Kodi inu mukuchita amuna
anzanu ukwati Ndi kutseka njira
(pakuchita chifwamba) Ndi
kuchita zoipa m'mabwalo anu
Osonkhanirana?" Koma yankho la
anthu Ake silidali lina koma
Ibrahim pamene adasamuka ku Iraki kumka ku palasitina ndi cholinga
chokafalitsa chipembedzo cha Mulungu kumeneko, Mulungu adamdalitsa ndi
mwana wotchedwa Isihaka ndi Yakubu mdzukulu wake. Ndipo adasankha
mbumba yake kukhala mbumba yotulukamo aneneri ndi atumiki. Ndipo mabuku
akumwamba ankavumbulutsidwa kwa aneneri ochokera m'mbumba yake.
Mulungu adamuchitira izi chifukwa cha kugonjera malamulo Ake kwathunthu.
Surat 29. Al-'Ankabut Juzu 20
845
T * s-ji-l T ^ Oj-&*Jl 0jj-*>
kunena kuti: "Tidzere ndi chilango
cha Mulungucho ngati uli mmodzi
wa oona".
30. (lye) adati: "Mbuye wanga
Ndipulumutseni kwa anthu
oononga".
31. Ndipo pamene atumiki athu
adamdzera Ibrahim ndi nkhani
yabwino (yoti Abereka Mneneri
Isihaka), Adanenanso: "Ndithu,
tiwaononga eni mudzi Uwu;
ndithu, iwowo ngochimwa."
32. (Mneneri Ibrahim)
adayankha: "Koma Mmenemo
muli Luti". Iwo adati: "Ife ndife
odziwa kwambiri za omwe Ali
m'menemo; ndithu, timpulumutsa
lye ndi banja lake kupatula mkazi
wake; lye ndi mmodzi wa otsalira
(woonongeka)".
33. Ndipo pamene atumiki athu
adamdzera Luti, Adawadandaulira
ndi kuwadera nkhawa; (Ndipo
iwo) adati: "Usaope ndipo
Usadandaule.Ndithu, ife
tikupulumutsa ndi Banja lako
kupatula mkazi wako; iye ndi
Mmodzi waotsalira (woonongeka)".
34. "Ndithu, ife tiwatsitsira
chilango Choipa kuchokera
kumwamba eni mudzi Uwu
chifukwa cha kuchimwa kwawo
(ndi Kuukira malamulo a Mulungu)".
®^?uA)t
"W*
Surat29.Al-'Ankabut Juzu20
846
Y • ^£-1 Y ^ o^-SoJl 5jj--
35. Ndipo ndithu, tidasiya
chizindikiro Mmenemo
choonekera Kwa anthu anzeru.
36. Ndipo ku Madiyani
(tidatumako) m'bale Wawo Shuaibu,
ndipo adati: "E, inu Anthu anga!
Mpembedzeni Mulungu ndipo
Opani tsiku lachimaliziro Musanke
muononga padziko."
37. Koma adamutsutsa. Ndipo
kugwedezeka Kwa nthaka
kudawachotsa moyo wawo, Ndipo
kudawachera ali gwadegwade
M'nyumba zawo ( atafa).
38. Nawonso Adi ndi Asamudu
(Tidawaononga). Mokhala mwawo
Mukudziwika kwa inu.Satana
Adawakometsera zochita zawo
(Zoipa), ndipo adawatsekereza
kunjira (Zabwino) chikhalirecho
adali openya, (Anzeru zawo).
39. Momwemonso Kaaruni,
Farawo Ndi Hamana
(adaonongedwa). Ndithu,
Adawadzera Musa ndi zozizwitsa,
(Zooneka) koma adadzikweza pa
dziko. Komatu sadathe
kumpambana (Mulungu
Pomulepheretsa Kuwalanga).
40. Choncho aliyense wa iwo
tidamlanga Ndi machimo ake. Ena
a iwo Tidawatumizira chimphepo
chamiyala; Ena a iwo
adachotsedwa moyo ndi Mkuwe;
-A
3®3^&3&&>
Surat29. Al-'Ankabut Juzu 21
847
Y 1 *ji-l T <* O^iCyJl 5jj-»
ena a iwo tidawadidimiza M'nthaka,
ndipo ena a iwo tidawamiza
(M'madzi). Si Mulungu amene
Adawachitira zoipa, koma
adadzichitira Okha zoipa.
41. Fanizo la amene adzipangira
milungu Yabodza kusiya Mulungu
weniweni, Lili ngati fanizo la
kangaude (yemwe) Wadzipangira
nyumba (kuti imsunge, pomwe
Nyumbayo siingathe kumsunga
m'nyengo Yozizira kapena
yotentha), ndithu, nyumba Yomwe
ili yofooka kwambiri ndi nyumba
ya Kangaude, akadakhala akudziwa. 1
42. Ndithu, Mulungu akudziwa
kupembedza Kwawo zinthu zina
kusiya lye, iye Ngwamphamvu
zoposa, Ngwanzeru zakuya.
43. Ndipo amenewa ndimafanizo
(omwe) Tikuwaponyera anthu.
Sangawazindikire Kupatula odziwa.
44. Mulungu adalenga thambo
ndi nthaka Mwachoona; ndithu;
m'menemo muli Zizindikiro kwa
okhulupirira.
45. Werengani zimene
zavumbulutsidwa Kwa iwe (za)
1 M'ndime iyi Mulungu akufanizira munthu wopembedza mafano ndicholinga
choti mafanowo adzimthangata pomudzetsera zabwino ndi kumchotsera
zoipa, kuti ali ngati kangaude yemwe wamanga nyumba ndi cholinga choti
imteteze kuchisanu ndi kutentha pomwe nyumbayo njofooka yomwe siingathe
kumteteza kuchisanu kapena kudzuwa. Izi zili chimodzimodzi ndi wopembedza
mafano. Mafanowo sangamudzetsere zabwino kapena kumchotsera zoipa.
Siirat 29. Al-'Ankabiit Juzu 21
848
t ^ tji-t Y ^ O^-^jJl djj--
m'buku, ndipo pemphera Swala;
ndithu, swala (ikapempheredwa
Moyenera) imamtchinjiriza
(Woipempherayo) kuzinthu zauve
ndi Zoipa. Ndipo kukumbukira
Mulungu, Ndi chinthu
chachikulu.Ndipo Mulungu
Akudziwa zimene mukuchita.
46. Ndipo musatsutsane ndi
anthu a Buku Koma kutsutsana
kwabwino kupatula Amene achita
zoipa mwa iwo. Ndipo Nenani:
"Takhulupirira zomwe
Zavumbulutsidwa kwa ife ndi
zomwe Zavumbulutsidwa kwa inu,
ndipo Mulungu Wathu ndi
Mulungu wanu ndi M'modzi;
ndipo ife Ndife ogonjera lye."
47. Ndipo umo ndimomwe
Takuvumbulutsira Buku (ili la
Qur'an). Ndipo amene tidawapatsa
Buku, (Ili lisadadze,monga Taurat
ndi Injili), Akulikhulupirira;
akulikhulupiriranso Ena mwa awa
(Arabu omwe Sitidawapatse
Buku). Ndipo sangakane ma Ay a
athu kupatula osakhulupirira.
48. Ndipo iwe sumawerenga
buku lililonse, Ili lisanadze; Ndipo
sudalilembe ndi Dzanja lako
lakumanja. Zikadatero Ndiye kuti
anthu Achabe akadakaikira. l
1 Akadakhala kuti umawerenga ndi kulemba pamenepo pakadakhala
poyenera kwa osakhulupirira kukaikira Qur'an. Ndime iyi ikufotokoza
Siirat 29. A1-' Ankabut Juzu 21
849
t WjA-i rs o^-^idj^-
49. Koma izi ndi aya Zathu
zoonekera poyera (Zomwe
nzovomerezeka) m'zifuwa za
Amene apatsidwa nzeru.Ndipo
sangazikane Aya (ndime) zathu
koma achinyengo.
50. Ndipo akunena: "Kodi
bwanji sizinatsitsidwe Kwa iye
zozizwitsa kuchokera kwa Mbuye
Wake?" Nena: "Zozizwitsa zili
kwa Mulungu; Ndipo ine ndine
mchenjezi woonekera, (Ndilibe
mphamvu zokudzetserani
Zozizwitsa koma pokhapo
Mulungu Atafuna)".
51. Kodi sizidawakwanire kuti
Takuvumbulutsira buku (ili)
lomwe Likuwerengedwa kwa iwo?
Ndithu, M'zimenezo muli
chifundo ndi phunziro Kwa anthu
okhulupirira.
52. Nena: "Mulungu akukwana
kukhala mboni Pakati panga ndi
inu;akudziwa za Kumwamba ndi
zapansi ndipo amene
Akukhulupirira zachabe ndi kukana
Mulungu, iwowo ndiwo otayika.
53. Ndipo akukupempha kuti
Chilango chidze mwachangu;
Kukadapanda kuti kudaikidwa
k£&
momveka kuti Mtumiki adali wosadziwa kulemba ndi kuwerenga koma
adamdzetsera Buku ili lomwe m'kati mwake muli nkhaninso za anthu akale
ndi zinthu zina zobisika. Choncho umenewu ndi umboni waukulu
wovomereza kuti iye ndi Mtumikidi wa Mulungu.
Surat29.Al-'Ankabut Juzu21
850
Y ^ ^^*-^ t ^ £Jy&jt\ 5jj^
Nthawi yodziwika, chilango
Chikadawadzera. Ndipo ndithu,
Chidzawadzera mwadzidzidzi
Asakudziwa.
54. Akukupempha kuti chilango
chidze Mwachangu; ndithu, Jahena
idzawazinga Osakhulupirira.
55. Tsiku limene
chidzawavindikira Chilango
kuyambira kumwamba mpaka
Pansi pamiyendo yawo; ndipo
adzanena: "Lawani (malipiro a)
zomwe munkachita."
56. E, inu akapolo Anga amene
mwakhulupirira! Ndithu, nthaka
yanga njophanuka; (Mukhoza kupita
dziko lina ngati m'dziko Lanulo
simupeza mwayi wopembedza
Mulungu mokwanira); ndipo Ine
ndekha Ndipembedzeni.
57. Chamoyo chilichonse
Chidzalawa imfa. Kenako
Mudzabwezedwa kwa Ife.
58. Ndipo amene akhulupirira
ndi kumachita Zabwino ndithudi
tidzawakhazika m'zipinda Za ku
Munda Wamtendere, momwe
pansi pake Pakuyenda mitsinje;
adzakhala m'menemo Muyaya.
Taonani kukhala bwino malipiro a
ochita zabwino!
59. Amene adapirira Ndi
kusamira kwa Mbuye wawo.
*uS®
%£&$&*&$<&&
%&&&&
®vM'^&&&>&^\
Surat 29. Al-'Ankabut Juzu 21 I 851 I * \ *>» M o^&idi 5j^
60. Ndi zamoyo zingati zomwe
sizidzipezera Riziki lake. Mulungu
akuzipatsa izo Pamodzi ndi
inunso.Ndipo lye Ngwakumva;
Ngodziwa.
61. Ndipo ngati utawafunsa
(kuti): "Kodi ndani Adalenga
thambo ndi nthaka, ndi kugonjetsa
Dzuwa ndi mwezi? Ndithu anena:
"Ndi Mulungu". Nanga
akutembenuzidwira Kuti?
62. Mulungu amamtambasulira
riziki amene Wamfuna mwa
akapolo Ake, ndi Kumchepetsera
(amene wamfunanso). Ndithu,
Mulungu Ngodziwa kwambiri Za
chilichonse.
63. Ndipo ngati utawafunsa
(kuti): "Kodi Ndani amene
akutsitsa madzi kuchokera
Kumitambo ndi kuiukitsa nthaka
ndi madziwo Pambuyo pokhala
yachilala?" Ndithu, anena: "Ndi
Mulungu." Nena: "Kuyamikidwa
Konse nkwa Mulungu." Koma
ambiri a Iwo sazindikira.
64. Ndipo moyo uwu
wapadziko lapansi Suli kanthu,
koma chibwana ndi masewera.
Ndipo Nyumba ya tsiku la
chimaliziro, Ndiwo moyo
weniweni, Akadakhala akudziwa.
65. Ndipo akakwera m'chombo
(ndi kukumana Ndi zoopsa),
£#'«& &»&&&$$
Surat 29. Al-'Ankabut Juzu 21
852
Y \ *j£-» Y ^ o^-£*)l o jj~>
amampempha Mulungu
Modzipereka ndikumuyeretsera
pempho. Koma akawapulumutsa
ndi kuwafikitsa Kumtunda, iwo
amayambanso Kumuphatikiza
Mulungu ndi mafano.
66. Posathokoza zimene
tawapatsa. Aleke Asangalale (ndi
zoipa zawozo); Posachedwa
adzadziwa.
67. Kodi saona kuti dziko lawo
(mzinda wa Makka) talichita
kukhala lopatulika, lamtendere
Pomwe anthu ena
akutsompholedwa M'mphepete
mwawo! Kodi akukhulupirira
Zachabe ndi kuukana Mtendere wa
Mulungu?
68. Kodi wachinyengo
wamkulu ndani woposa Amene
akupekera bodza Mulungu, kapena
Kutsutsa choona chikamdzera?
Kodi si Jahena yomwe idzakhala
Malo a osakhulupirira?
69. Ndipo amene akulimbikira
m'njira yathu, (Polimbana ndi
satana, ndi mzimu woipa Ndi
zilakolako zoipa zam'thupi, ndi
cholinga Chofuna kukondweretsa
Mulungu) ndithu Tiwaongolera ku
njira Zathu. Ndipo ndithu, Mulungu
ali pamodzi ndi ochita zabwino.
Siirat 30. Ar-Rum Juzu 21
853
iw>» r* pj^oj^
SURAT AR-RUM XXX
Surayi yayamba ndi kukamba zakugonja kwa Aroma pankhondo
yomwe idali pakati pawo ndi Aperezi (Persia). Yafotokozanso kuti
nawonso Aroma adzagonjetsa adani awowo m'zaka zowerengeka.
Ndipo zidachitikadi monga momwe Qur'an idafotokozera.
Ichi chidali chozizwitsa chachikulu chosonyeza kuona kwa
utumiki wa Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale naye)
ndi zimene Qur'an ikufotokoza.
Komanso Surayi yafotokoza za mkangano womwe uli pakati pa
chipani cha Mulungu ndi chipani cha Satana. Ndithu, mkangano
umenewu ngwakalekale. Ndipo malinga kuti choona ndi chonama,
chabwino ndi choipa zonse zilipo, nkhondo padziko lapansi
siidzatha. Nkhondo idzapitirira mpaka m'tsogolo chifukwa chakuti
satana akulimbitsa abwenzi ake ndi athandizi ake kuti azimitse
dangalira la Chauta, ndi kulimbana ndi ulaliki wa Aneneri. Surayi
yafotokozanso zisonyezo ndi maumboni osonyeza kupambana kwa
chonama m'mibadwo yosiyanasiyana. Imeneyi ndiyo njira ya
Mulungu, ndipo panjira ya Chauta simungapeze kusintha kulikonse.
Tero choona chiyenera kupambana chonama ngakhale patapita
nthawi yaitali.
Surayi yafotokozanso za tsiku lomalizira, ndi mabwerero
oipa a anthu osakhulupirira pomwe Asilamu adzakhala m'minda
yamtendere akusangalatsidwa. Oipa adzaponyedwa kuchilango cha
moto. Ndipo amenewa ndiwo malekezero a anthu osakhulupirira.
Surayi yafotokozanso zina mwa zisonyezo za chilengedwe
ndi zisonyezo zobisika zomwe zikulangiza mphamvu ya Mulungu
yoposa, ndi umodzi Wake; zomwezonso zikusonyeza ukulu ndi
kutukuka kwa Chauta yemwe nkhope zikumlambira. Ndipo
yapereka mafanizo osiyanitsa pakati pa amene akupembedza
Mulungu Wachifundo, ndi omwe akupembedza mafano.
Surayi yamaliza ndi kufotokoza za akafiri a Achikuraishi
omwe zisonyezo ndi atetezi sizidawathandize ngakhale kuti
adaona zizizwa zosiyanasiyana ndi maumboni oonekera poyera.
Sadalingalire konse; ndipo zonsezi nchifukwa chakuti iwo adali
ngati akufa.Samamva ndi kupenya komwe.
Surat 30. Ar-Riim Juzu 21
854
Y \ *j*-i
r • ^ jj)i dj>^
Surat Ar-Riim XXX
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Alif-Lam-Mim}
2. Aroma agonjetsedwa (ndi
Aperezi). 2
3. M'dziko loyandikira (kwa
Arabu Lomwe ndi dziko la
Shamu). Nawonso Pambuyo
°&&\&&\&w
J^
©5-M
1 Surayi yayamba ndi zilembo za alifabeti posonyeza kuti Qur'an yalembedwa
kupyolera m'malemba amenewa omwe Arabu amawayankhula mofewa.
Koma Akuraishi adalephera kulemba Buku limeneli pomwe malembo ake
akuwadziwa.
2 Surayi idapatsidwa dzina loti Rum chifukwa chakuti idalosera kuti Aroma
adzagonjetsa Aperezi. M'menemo nkuti pamene surayi inkavumbulutsidwa
ndi kulosera kupambana kwa Aroma iwo adali atagonjetsedwa kale ndi
Aperezi, kugonjetsedwa zedi kotero kuti maiko awo ambiri adalandidwa ndi
Apereziwo. Surayi idavumbulutsidwa ku Makka m'chaka chachisanu
nchimodzi (6) kapena chisanu ndichiwiri (7) Mtumiki asanasamuke. Aroma ndi
anthu akale zedi; amalamulira maiko ambiri. Mzinda wawo waukulu
umatchedwa Roma m'dziko la Italy.
Padali mkangano pakati pamfumu ziwiri: Mfumu ya Aroma ndi Mfumu ya
Aperezi mkanganowo udayamba m'chaka cha 602 A.D, Ndipo pamene
adamenyana nkhondo Aperezi adagonjetsa Aroma. Ndipo kupambana kwa
Aperezi kutamveka m'Makka, Arabu opembedza mafano adakondwa
kwambiri poti naonso Aperezi adali kupembedza mafano ngati iwo. Arabu
opembedza mafanowo adati kwa Asilamu ndi Akhrisitu: "Anthu a mabuku
ngati inu mwagonjetsedwa ndi anzathu opembedza mafano, choncho nafenso
tikugonjetsani inu Asilamu posachedwa."
Qur'an idalengeza ndime izi ziwiri zomwe mkati mwake muli ulosi uwiri: Ulosi
woyamba nkuti m'nyengo yosapyolera zaka zisanu ndi zinayi (9) Aperezi
adzagonjetsedwa ndi Aroma. Ndipo ulosi wachiwiri ukuti Asilamu
adzagonjetsa Arabu opembedza mafano amumzinda wa Makka. M'chaka cha
624. Hirakla, mfumu ya Aroma adagonjetsa mzinda wa Madiyani m'dziko la
Aperezi. Ndipo m'chaka chomwecho naonso Asilamu omwe adali 313
adagonjetsa gulu lankhondo la Arabu opembedza mafano omwe kuchuluka
kwawo kudali 1,000 pankhondo yomwe idachitikira pamalo wotchedwa Badri.
Ndipo opembedza mafanowo adagonjetsedwa moipa. Potero ulosi umene
Qur'an idalosera udakwaniritsidwa. Ndipo ichi chidali chinthu chozizwitsa zedi,
chomwe chimasonyeza kuti Qur'an ndi Mawudi a Mulungu.
Surat 30. Ar-Rum Juzu 21
855
Y> ij±\
r * fjj\ ijj~>
pogonjetsedwa kwawo,
Adzagonjetsa (Aperezi).
4. Mzaka zochepa (zosapyolera
10). Zonse Nza Mulungu,
pambuyo ndi patsogolo
(Pankhondoyo). Ndipo tsiku
limenelo Okhulupirira
adzasangalala.
5. Ndi chithandizo cha Mulungu
(chimene Iwo adzapatsidwa,
chomwe Ndikugonjetsa Akuraishi
tsiku Lomwelo). (Mulungu)
amamthandiza Amene wamfuna,
ndipo lye Ngwamphamvu zoposa;
Ngwachisoni.
6. Hi ndilonjezo la Mulungu
(loona pa Okhulupirira). Mulungu
saswa lonjezo Lake. Koma anthu
ambiri sadziwa.
7. Akudziwa zoonekera
(zokhazokha) za Moyo wadziko
lapansi (zomwe Amadalira
pamoyo wawo. Monga Ulimi,
malonda, zomangamanga ndi Zina
zotero). Ndipo iwo salabadira Za
tsiku la chimaliziro.
8. Kodi salingalira mwa iwo
okha (nkuona Kuti) Mulungu
sadalenge thambo ndi Nthaka ndi
zapakati pake, koma
Mwachilungamo, ndiponso
kwanthawi Yoikidwa? Ndithu,
anthu ambiri Ngotsutsa
zakukumana ndi Mbuye wawo.
"i^T <iS"l »>\'h ii »<
©t35Kft Muslin >3f
Surat 30. Ar-Rum Juzu 21
856
n *>i
r • ?jj\ oj^
9. Kodi sadayende pa dziko
nkuona Momwe adalili malekezero
a omwe Adaliko patsogolo pawo?
Adali Anyonga zambiri kuposa
iwo. Adailima nthaka ndi
kumangapo Zomangamanga
kuposa momwe Iwo
adamangirapo. Ndipo aneneri awo
Adawadzera ndi zizindikiro
zoonekera (Koma adawatsutsa,
ndipo Mulungu Adawawononga).
Choncho Mulungu sadali
Owapondereza koma iwo
ankazipondereza Okha.
10. Kenako malekezero a
amene adaipitsa adali Chilango
choipa kamba koti adakanira Aya
za Mulungu ndipo Ankazichitira
chipongwe.
11. Mulungu ndi Yemwe
akuyambitsa (Njira ya) kulenga
(zolengedwa), Kenako
adzakubwezanso (kulengako
Pambuyo pa imfa yawo), kenako
Mudzabwezedwa kwa lye (kuti
Mudzaweruzid we) .
12. Ndipo tsiku limene nthawi
ya chiweruzo (Kiyama)
idzakwana, oipa adzataya Mtima
(zakupeza mtendere wa Mulungu).
13. Ndipo sadzakhala ndi
aomboli ochokera M'mafano awo,
ndipo mafano awowo
Adzawakana.
'*$£&&&*&>
*&,#*$&$&'&«
Surat 30. Ar-Rum Juzu 21
857
n *>i
r • f jjji oj^
14. Ndipo tsiku limene nthawi
ya chiweruzo (Kiyama)
idzakwana, tsiku limenelo
Adzalekana (ena kukalowa
kumunda Wamtendere, pomwe ena
akalowa Kumoto).
15. Koma amene akhulupirira
ndi Kumachita zabwino, adzakhala
M'minda ya zipatso ndi maluwa
Akusangalatsidwa.
16. Ndipo amene
sadakhulupirire ndi Kutsutsa aya
Zathu ndi za kukumana ndi tsiku
Lomaliza, iwo adzaperekedwa ku
Chilango cha moto.
17. Choncho, lemekezani
Mulungu pamene Mukulowa
m' nthawi za usiku (Popemphera
Magaribi ndi Isha); ndi Pamene
mukulowa m' nthawi ya
M'bandakucha (popemphera
Pemphero la Fajiri).
18. Kutamandidwa konse,
kumwamba ndi Pansi nkwa
Mulungu. Ndipo (Mulemekezeni)
m' nthawi ya madzulo
(Popemphera Aswiri) Ndi pomwe
mukulowa M' nthawi yamasana
(Zuhuri).
19. (lye) amatulutsa chamoyo
kuchokera Mchakufa, ndipo
amatulutsa chakufa Kuchokera
m' chamoyo, ndipo Amaukitsa
nthaka pambuyo pachilala Chake.
o 1
<j&% ^aiUii (io^ii 4$i
Surat 30. Ar-Rum Juzu 21
858
Y> *>i
r • fJj* 1 *J>"
Ndipo momwemonso
Mudzatulutsidwa (m'manda).
20. Ndipo zina mwazizindikiro
Zake (zosonyeza Mphamvu Zake
zoposa), ndiko Kukulengani
kuchokera ku dothi kenako Inu
nkukhala anthu omwe mukufala
(Ponseponse).
21. Ndipo zina mwazizindikiro
Zake (Zosonyeza chifundo Chake
kwa inu) Ndiko kukulengerani
akazi a mtundu wanu Kuti
mukhazikike (mitima yanu) Kwa
iwo, ndipo adaika Pakati panu
chikondi ndi chisoni. Ndithu,
mzimenezi muli zizindikiro Kwa
anthu amene amalingalira.
22. Ndipo zina mwazizindikiro
Zake (Zosonyeza kukhoza Kwake)
ndiko Kulenga kwa thambo ndi
nthaka Ndikusiyana kwa
ziyankhulo zanu ndi Utoto (wa
makungu anu; chikhalirecho
Mudalengedwa kuchokera kwa
Munthu m'modzi). Ndithu,
m'zimenezi Muli zizindikiro kwa
odziwa.
23. Ndipo zina mwa zizindikiro
Zake (Zosonyeza luntha Lake),
ndiko Kukupatsani mpumulo
watulo usiku, Ndi (kudzuka) usana
ndi kufunafuna Kwanu zabwino
Zake. Ndithu, M'zimenezo muli
zisonyezo kwa Anthu amene
Surat 30. Ar-Rum Juzu 21
859 11 *><
r • f jjii 5j>-
amamva (Ndi kuthandizidwa
ndikumvako).
24. Ndipo zina mwazizindikiro
Zake (Zosonyeza mphamvu Zake
zoposa) Ndiko kukusonyezani
kung'anima Komwe
kumakuchititsani mantha, Ndi
kukupatsani chiyembekezero
(Chakudza kwa mvula). Ndipo
Amatsitsa madzi kuchokera
kumwamba. Kotero kuti amaukitsa
nthaka ndi Madziwo pambuyo pa
chilala chake (Nthakayo). Ndithu,
m'zimenezi Muli zizindikiro kwa
anthu ozindikira.
25. Ndipo zina mwazizindikiro
Zake (Zosonyeza kukhoza
Kwake), ndiko Kuti thambo ndi
nthaka zaima mwa Lamulo Lake.
Kenako akadzakuitanani; Kuitana
kamodzi nthawi imeneyo inu
Mudzatuluka m' nthaka.
26. Ndipo onse akumwamba ndi
a padziko Lapansi, Ngake. Onse
amamvera lye.
27. Ndipo lye ndiamene
adayambitsa Zolengedwa. Ndipo
ndi Yemwe Adzazibwerezenso
(kachiwiri). Ndipo
Kuzibwerezako, nkosavuta kwa
lye ndipo, AH ndi mbiri yabwino
Kumwmba ndi pansi.Ndiponso lye
Ngwamphamvu zoposa
Ngwanzeru zakuya.
V>"'i -<1
"•*"< 9 '• ,»"i.'"V1ii£ "" > . i\ ' 9 '
Surat 30. Ar-Rum Juzu 21
860
n frji-i
r • f jjj» Sjj--
28. Akuponyerani fanizo la
chikhalidwe Chanu. Kodi
(akapolo) amene manja Anu
akumanja apeza ali ndi gawo
Pachuma chimene takupatsani
kotero Kuti mumagawana
chimenecho Molingana? Kodi
mumawaopa monga Momwe
muoperana wina ndi mzake?
(Nanga nchotani inu kuti
mumuyese Mulungu kuti ali ndi
amzake Mwa akapolo Ake?) Umo
ndimomwe Tikulongosolera aya
(ndime Zathu) Kwa anthu
ozindikira.
29. Koma amene adadzichitira
zoipa okha, Atsata zofuna zawo
popanda kudziwa. Kodi ndiyani
angamulungamitse amene
Mulungu wamsiya kuti asokere
(Chifukwa chakusafuna kwake
Kuongoka?) Ndipo iwo sadzakhala
ndi Apulumutsi.
30. Lunjika nkhope yako
kuchipembedzo Moyenera; (pewa
kusokera kwa okana Mulungu.
Dzikakamize ku) chilengedwe
Chimene Mulungu adalengera
anthu. (Ichi nchipembedzo cha
Chisilamu Chomwe nchoyenerana
ndi chilengedwe Cha
munthu).Palibe kusintha
M' chilengedwe cha zolengedwa za
Mulungu. Ichi ndi chipembedzo
choona (Cholungama). Koma
anthu ambiri sadziwa.
"
<_>>»
®h£$i4-&.
»< >>'\'*'i
Surat 30. Ar-Rum Juzu 21 861 * > *>»
r . ?jj\ oj^
31. (Lunjikani nkhope zanu)
modzichepetsa Kwa lye ndipo
muopeni (Potsatira malamulo
Ake). Pempherani Swala, ndipo
musakhale mwa opembedza
Mafano (Amushirikina),
32. Mwa omwe agawa
chipembedzo Chawo nkukhala
mipatukomipatuko; Gulu lililonse
likusangalalira chomwe Lili nacho.
33. Ndipo mavuto akawakhuza
anthu, Amampempha Mbuye
wawo Modzichepetsa kwa lye.
Kenako Akawalawitsa mtendere
wochokera Kwa lye, pamenepo
ena a iwo Amamuphatikiza Mbuye
wawo (Ndi mafano).
34. Posathokoza zimene
tawapatsa. Choncho Sangalalani
(ndi zimene mukuzifunazo);
Posachedwapa Mudziwa (kuipa
kwake).
35. Kodi kapena tidawatsitsira
umboni Womwe ukufotokoza
zomwe adali Kumuphatikiza nazo
lye (Mulungu).
36. Ndipo anthu tikawalawitsa
mtendere, Amausangalalira. Koma
choipa Chikawapeza, chifukwa cha
zomwe manja Awo atsogoza,
pamenepo iwo amataya mtima
(Kuti sangapezenso zabwino za
Mulungu).
i 9 *~\' f'Z&l' 9< { S9 9 9
il&KiSa&wqS^
Surat 30. Ar-Rum Juzu 21
862
Y^ j.j*-i
r • f jjii oj>^
37. Kodi saona kuti Mulungu
Amamchulukitsira riziki yemwe
Wamfuna, ndi kumchepetsera
(Yemwe wamfuna.) Ndithu
m'zimenezi, muli zisonyezo Kwa
anthu okhulupirira.
38. Choncho mpatseni gawo
lake wachibale, M'mphawi ndi
wapaulendo (Amene alibe
chokamfikitsa kwawo). Zimenezo
nzabwino kwa amene Akufuna
chiyanjo cha Mulungu, Ndipo iwo
ndiwo opambana.
39. Ndipo chuma chimene
mukupatsana M'njira yamphatso
kuti Chichuluke m'chuma cha
anthu, kwa Mulungu sichichuluka.
Koma (chuma) Chimene
muchipereka m'njira ya Zakati uku
mukufuna chiyanjo cha Mulungu
(chimachuluka). I wo wo ndi
Amene adzapeza mphoto
yochuluka.
40. Mulungu ndi Yemwe
adakulengani. Kenako
adakupatsani (zokuthandizani Kuti
mukhale ndi moyo). Kenako
Adzakupatsani imfa (kuti mulowe
M'manda). Ndipo kenako
Adzakuukitsani (kuti
mukaweruzidwe Pazomwe
mumachita). Kodi mwa Amene
mukuwaphatikiza ndi Mulungu,
Alipo yemwe angachite
chilichonse M'zimenezi? Wayera
Surat 30. Ar-Rum Juzu 21
863
n *>i
r ♦ ?jj\ 5j^
lye (Mulungu) ndipo Watukuka ku
zimene akumphatikiza.
41. Chisokonezo chaonekera
pamtunda Ndi panyanja chifukwa
cha zimene Manja a anthu achita,
kuti awalawitse (Chilango cha)
zina zomwe adachita; Kuti iwo
atembenukira (kwa Mulungu).
42. Nena: "Yendani padziko ndi
kuyang'ana Momwe adalili
mathero a omwe adalipo Kale.
Ambiri a iwo adali ophatikiza
Mulungu ndi mafano."
43. Lungamitsa nkhope yako ku
chipembedzo Choona lisanadze
tsiku losabwezedwa Lochokera
kwa Mulungu. Tsiku limenelo
(Anthu) adzagawikana, (abwino
Akalowa kumunda wamtendere,
pomwe Oipa akalowa kumoto).
44. Amene sanakhulupirire,
kuipa kwa Kusakhulupirira kwake
kuli pa iye (Mwini). Ndipo amene
achita zabwino Iwo akudzikonzera
okha (zabwino)
45. Kuti awalipire zabwino
Zake amene Akhulupirira ndi
kuchita zabwino. Ndithu, Iye
sakonda akafiri. (Osakhulupirira).
46. Ndipo zina mwazisonyezo
Zake (Zosonyeza mphamvu Zake
ndi chifundo Chake). Ndiko
kutumiza mphepo yodza ndi
^99 9' 9><
Surat 30. Ar-Rum Juzu 21
864
Y1 tj*r\
r • fjj\ ojj^
nkhani Yabwino (yakuti mvula
ivumbwa) ndi kuti Akulawitseni
chifundo Chake, ndi kuti Zombo
ziyende (panyanja) mwa lamulo
Lake, ndi kuti mufunefune
zabwino Zake ndi Kutinso
muthokoze (mtendere Wake
Pomumvera ndi kumpembedza lye
Yekha).
47. Ndipo, ndithu tidatuma
aneneri kwa Anthu awo patsogolo
pako. Choncho (Mneneri aliyense)
adawadzera anthu Ake ndi
maumboni oonekera poyera,
(Osonyeza kuona kwawo. Koma
adawakana). Ndipo
tidawawononga amene adalakwa.
Ndikofunika kwa Ife kupulumutsa
Okhulupirira.
48. Mulungu ndiyemwe
akutumiza mphepo Yomwe
imagwedeza mitambo
mwamphamvu, Ndipo
akuibalalitsa kumwamba mmene
Akufunira. Amaigawa
zigawozigawo (Kufikira) uyiona
mvula ikutuluka mkati mwake
(Mitamboyo). Ndipo (Mulungu)
akaitsitsa kwa Amene wamfuna
mwa akapolo Ake, pamenepo Iwo
amakondwa ndi kusangalala.
49. Ngakhale kuti
isadawatsikire, Adali otaya mtima
ndi Kutekeseka kwambiri.
Surat 30. Ar-Rum Juzu 21
865
tl *>»
r • fjj\ ijj~>
50. Choncho, yang'ana
(molingalira) zizindikiro Za
chifundo cha Mulungu momwe
Akuukitsira nthaka (pomeretsa
mmera) Pambuyo pachilala chake.
Ndithu, lye ndi Yemwe Akuukitsa
akufa. Ndipo lye Ngokhoza
Chilichonse (palibe chokanika kwa
lye.)
51. Ndipo, ndithu, tikatumizira
mphepo (Yoononga mmera)
nkuuona pambuyo pake Uli
wachikasu, akadakhala akupitiriza
Kukana Mulungu (chifukwa
chokwiyitsidwa Ndi zimenezi.)
52. (Usadandaule ndi makani
awo). Ndithu, I we sungachititse
kuti amve akufa (Kuitana kwako).
Ndiponso sungachititse Kuti amve
agonthi kuitana pamene
Akutembenukira nakuyang'anitsa
Msana (osafuna kumva mawu ako).
53. Ndipo iwe sungathe
kuwaongolera akhungu
M'kusokera kwawo. Sungachititse
kuti Amve koma okhawo amene
akhulupirira Aya Zathu. Iwowo
ndiwo Odzipereka.
54. Mulungu ndi Yemwe
adakulengani Kuchokera kudontho
lofooka; kenako Adakupatsani
mphamvu pambuyo Pakufooka,
ndipo pambuyo pamphamvu
Adakupatsani kufooka ndi imvi,
*<^S;J-S£ua#*tf
V
Surat 30. Ar-Rum Juzu 21
866 n &\
r • ^j\ oj>-»
(lye) Akulenga chimene wafuna.
Ndipo lye Ngodziwa kwambiri;
Ngokhoza Chilichonse. 1
55. Ndipo tsiku limene
chiweruziro (Kiyama)
chidzachitika, oipa adzakhala
Akulumbira (kuti) sadakhale
(padziko Lapansi) koma ola
limodzi. Umo Ndimomwe
amatembenuzidwira (Kuchokera
kunjira ya choonadi).
56. Ndipo amene apatsidwa
nzeru ndi Chikhulupiriro,
adzanena: "Ndithu, Inu mudakhala
m'chilamulo cha Mulungu kufikira
tsiku louka ku imfa; Tsono ili ndi
tsiku louka ku imfa koma Inu
simunali kudziwa".
57. Tsiku limenelo, madandaulo
a omwe Adzichitira chinyengo
sadzawathandiza Ndipo
sadzafunsidwa kuti
Amukondweretse Mulungu (ndi
kulapa Kwawo.)
58. Ndipo ndithu, tawaponyera
anthu mafanizo A mtundu
uliwonse m'Qur'an iyi. Ndipo,
1 M'ndime iyi akufotokoza kuti adalenga anthu kuchokera m'madzi ofooka.
Ndipo kuchokera pamenepo chilengedwe chimasinthasintha pokhala khanda,
mnyamata kenako nkukhala wamkulu wanyongazake ndipo mapeto ake
nkukhala nkhalamba ya imvi, yofooka. Zonsezi zimachitika mwa chifuniro cha
Mulungu popanda munthu kuikapo dzanja.
2 . Ndime iyi ikufotokozera kuti anthu ochita zoipa akadzaukitsidwa m'manda
ndi kuona zoopsa zothetsa nzeru, adzaganiza kuti pamoyo wa padziko
lapansi sadakhale nthawi yaitali koma ola limodzi basi. Izi nchifukwa
chamavuto omwe adzakumana nawo patsiku limenelo.
Surat 30. Ar-Rum Juzu 21
867 n *&\
r • fjj\ 5j>-»
ndithu, ukawabweretsera Mtsutso
uliwonse, anena omwe
Sadakhulupirire: "Inu sikanthu,
koma Ndinu anthu ochita
zachabe".
59. Mmenemo ndi momwe
Mulungu Akudindira (chidindo)
m'mitima mwa Amene sazindikira.
60. Choncho pirira (iwe
Mtumiki Kumasautso awo).
Ndithu, lonjezo La Mulungu,
nloona, ndipo asakugwetse
Mphwayi amene alibe
chikhulupiriro Chotsimikiza
(Mulungu ndi Mtumiki Wake).
e <^^i<aK$a*
&*&&}&&&&&&
®&&$u$\
Siirat 31. Luqman Juzu 21
868
n *jh\
T ) OUiJ Ojj~t
Surayi yayamba ndi kufotokoza za Buku la Qur'an ndi zomwe
zili m'kati mwake monga chiongoko ndi chiflindo. Ndipo
ikufotokozanso chikhalidwe cha ochita zabwino, pomvera Chauta
ndi kukhulupirira tsiku lachimaliziro, ndi kutsimikizira kuti
kupambana kuli pa iwo.
Pankhaniyi yatsatizapo kufotokoza zakusokera kwa odzikuza ndi
kupereka mitsutso ndi zisonyezo kwa otsutsa, zosonyeza umodzi wa
Mulungu; Mleri wa zolengedwa monga kalengedwe kodabwitsa
kazam'dziko monga thambo, dzuwa, mwezi, nyenyezi, nthaka,
mapiri, nyanja, mitsinje ndi mmera, ndi zonse zimene munthu
akuziona zosonyeza luso la Mulungu ndi mphamvu Zake zoposa.
Surayi yamaliza ndi kuchenjeza anthu za tsiku loopsa lomwe
munthu sadzathandizidwa ndi ana ake kapena chuma chake.
Surat31. Luqman Juzu21
869
n *>i
V S OUii 5jj-j
Surat Luqman XXXI
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Alif-Lam-Mirn.
2. Izi ndi aya za Buku
Lokonzedwa bwino.
3. (Lomwe ndi) chiongoko ndi
chifundo Kwa ochita zabwino,
4. Amene akupemphera swala
ndi Kupereka chopereka (zakati)
omwenso Akutsimikiza za tsiku
lachimaliziro.
5. Iwowo ali pa chiongoko
chochokera Kwa Mbuye wawo;
ndipo iwowo Ndiwo opambana.
6. Koma alipo ena mwa anthu
amene Akusankha nkhani ya bodza
(Ndi kumaifotokoza kwa anthu)
Ndi cholinga choti awasokeretse
ku Njira ya Mulungu. Popanda
kuzindikira. Ndipo akuichitira
zachipongwe (njira ya Mulunguyi)
Iwo adzapeza chilango
chowasambula.
^c^T^ap
2;s&mi
o&g\^3^j
^
©ifi
Malembo awa akudziwitsa kuti Qur'an idalembedwa mwachidule chomveka
ndi kulozera kuti Bukuli lomwe ilo anthu anzeru zakuya akulephera kulemba,
lapangika kuchokera m'malembo amenewa omwe anthu akuwadziwa ndi
kugwiritsa ntchito. Ngati iwo ali ndi chipeneko kuti silidachokere kwa Mulungu,
koma kuti Muhammad (SAW) adangolilemba yekha ngakhale kuti adali
wosadziwa kulemba, atalemba Buku lawo longa ili. Malembo a Bukuli ndi
omwenso iwo amawadziwa. Komatu sangathe kulemba Buku longa ili
ngakhale anthu onse am'dziko lapansi atathandizana. Uwu ndi umboni
waukulu umene ukusonyeza kuti Bukuli lidachokera kwa Mulungu.
Siirat31. Luqman Juzu 21
870
n *>i
V \ OUii 5jj-»
7. Ndipo pamene aya Zathu
Zilakatulidwa kwa iye,
Akuzitembenuzira msana
modzikuza Ngati kuti sanazimve,
ngati kutinso M'makutu mwake
muli ugonthi Choncho muuze
nkhani ya chilango Chopweteka.
8. Ndithu, amene akhulupirira
ndi kumachita Zabwino, adzakhala
ndi minda Yamtendere.
9. Adzakhala m'menemo muyaya.
Hi Nlonjezo la Mulungu lomwe lili
loona. Ndipo Iye Ngwamphamvu;
Ngwanzeru Zakuya.
10. Adalenga thambo popanda
mizati Yomwe mukuiona. Ndipo
adaika mapiri M'nthaka kuti
isakugwedezeni. Ndipo (Iye)
adafalitsa nyama M'menemo
zamitundu yosiyanasiyana. Ndipo
tidatsitsa madzi kuchokera ku
Mitambo, choncho tidameretsa
m'menemo (M'nthaka)mmera
wokongola wamitundu
Yosiyanasiyana. ]
11. Izi (zonse) nzolengedwa za
Mulungu. Choncho,tandisonyezani,
nchiyani Adalenga amene sali
,»»<*fi
©,
M'ndime iyi Mulungu akutifotokozera kuti adalenga thambo monga lilili
m'kukula kwake ndi m'kuphanuka kwake ndi kulimba kwake popanda mizati
yolichirikiza. Ndipo inu anthu mukuliona mmene lili lopanda chilichonse
choligwira koma mphamvu za Mulungu Wamkulu Wapamwambamwamba.
Ndipo m'nthaka adaikamo mapiri akuluakulu kuti nthaka isamagwedezeke ndi
kumakusowetsani mtendere, kapena kumakugumulirani nyumba zanu. Ndipo
Mulungu adafalitsa padziko zamoyo zochuluka ndi kumeretsa mbewu
zosiyanasiyana. Zonsezi zikusonyeza mphamvu Zake zoopsa.
Surat31. Luqman Juzu 21
871
y\ frjA-i
t ^ ouiJ ojj^t
Mulungu. Koma Odzichitira okha
zoipa ali Mkusokera koonekera.
12. Ndipo ndithu, tidampatsa
Luqman Nzeru (ndipo tidati kwa
iye): "Thokoza Mulungu (pazimene
Wakupatsa)." Ndipo, amene
athokoza, Ndithu kuthokozako
Kumthandiza yekha, ndiponso amene
Akana (mtendere wa Mulungu
Pakusiya kuthokoza), ndithu,
Mulungu Ngwachikwanekwane
Ngotamandidwa
13. Ndipo (akumbutse) pamene
Luqman Adauza mwana wake
akumulangiza: "E, iwe mwana
wanga! Usaphatikize Mulungu ndi
mafano. Ndithu, Kumuphatikiza
(Mulungu), ndi Kuipitsa
kwakukulu."
14. Ndipo tamulangiza munthu
kwa makolo Ake (kuwachitira
zabwino) adamsenza (Pathupi) mai
wake ali wofooka Pamwamba
pakufooka. (Adamuyamwitsa) Ndi
kumusiyitsa patapita zaka ziwiri.
Ndithokoze Ine ndi makolo ako,
Kwa Ine nkobwerera.
©.
99 "\ i '< i V
1 M'ndime izi 13 mpaka 14 Mulungu akulamula munthu kuti achitire zabwino
makolo ake powamvera ndi kuwathandiza ngati ali osowa. Izi nchifukwa cha
kuti makolo ake adazunzika kwambiri pomulera iye makamaka mayi wake ndi
amene adazunzika kwambiri kuyambira pamene adatenga mimba yake
kufikira pamene adamusiyitsa kuyamwa. Choncho mverani makolo anu
pazimene akukulangizani zomwe sizili zolakwira Mulungu. Koma ngati
akukulangizani zolakwira Mulungu, musatsatire malangizo awowo, koma
khalani nawoni mwa ubwino.
Surat31. Luqman Juzu21 872 m^ ^ l
t\ ouii ojj--
15. Ndipo (makolo ako) ngati
Atakukakamiza kuti undiphatikize
Ine Ndi zomwe iwe sukuzidziwa,
Usawamvere; koma khala nawo
Padziko mwaubwino; ndipo tsatira
njira Ya amene atembenukira kwa
Ine. Ndipo Kenako kobwerera
kwanu nkwa Ine. Choncho
ndidzakuuzani zimene Mudali
kuchita.
16. "E, iwe mwana wanga!
Ndithu, (Chabwino ndi choipa cha
munthu) icho Ngakhale chitakhala
cholemera ngati Njere za mpiru
ndi kukhala m'kati Mwa thanthwe
kapena m'kati mwa Thambo,
kapena m'kati mwa nthaka,
Mulungu adzachibweretsa (ndi
Kumulipira amene adachita).
Ndithu, Mulungu Ngodziwa zinthu
zobisika, (Ndiponso) Ngodziwa
zinthu zoonekera.
17. E, iwe mwana wanga!
Pemphera moyenera, Lamula
zabwino, letsa zoipa, ndipo Pirira
ndi masautso amene akukhudza.
Ndithu zimenezo ndizinthu zofunika
Kuziikirapo mtima (munthu aliyense)
18. Ndipo usatembenuze tsaya
lako kwa anthu (Modzikweza,)
ndipo usayende padziko Monyada.
Ndithu, Mulungu sakonda Yense
wodzitukumula, wonyada.
19. Ndipo lingana m'kuyenda
kwako (Popanda kufulumiza
Surat 31. Luqman Juzu 21 I 873 I T ^ *jJt-i
x \ juii 5jj-*
kwambiri Kapena kuyenda
pang'onopang'ono); Ndipo tsitsa
mawu ako (Ukamayankhula),
chifukwa, mawu Okweza ngoipa
kwabasi). Ndithu mawu Oyipitsitsa
ndi mawu a bulu."
20. Kodi simuona kuti Mulungu
Adakugonjetserani zakumwamba
Ndi zapansi ndi kukukwaniritsirani
Chisomo Chake, chobisika ndi
Choonekera? Ndipo alipo ena mwa
Anthu amene akukangana Pa za
Mulungu popanda kuzindikira
Ngakhale chiongoko, ngakhalenso
BukuLounika. 1
21. Ndipo akauzidwa kuti:
"Tsatani zimene Mulungu
watsitsa," akunena: "Koma
Tikutsata zimene tidawapeza nazo
Makolo athu." Kodi ngakhale kuti
Satana akuwaitanira ku chilango
Chamoto (woyaka, adzatsatirabe)?
22. Ndipo amene akupereka
nkhope yake Kwa Mulungu
(amene akugonjera Mulungu
kwatunthu) ali ochita Zabwino,
ndiye kuti wagwira Chogwirira
cholimba. Ndipo mapeto A zinthu
zonse nkwa Mulungu basi.
^&39£ft#&
1 E, inu anthu! Ndithu, Mulungu Wolemekezeka adakupangirani zonse zili
kumwamba monga dzuwa mwezi, nyenyezi kuti muthandizike nazo. Ndipo
adakupangirani zonse zomwe zili m'nthaka monga mapiri, mitengo, zipatso,
mitsinje, ndi zina zambiri zosawerengeka kuti zonsezi zigonjere inu ndikuti
muthandizike nazo
Surat31. Luqman Juzu 21
874
tl ij*r\
t ^ ou£J ojj*>
23. Koma amene
sadakhulupirire (Mulungu ndi
Mtima wake wonse) choncho
Kusakudandaulitsekusakhulupirira
kwake. Kobwerera kwawo nkwa
Ife basi. Kumeneko Tidzawauza
zimene adachita. Ndithu, Mulungu
Ngodziwa zonse zam'zifuwa.
24. Tikuwasangalatsa pang'ono
(apo Padziko lapansi). Kenako
Tidzawakankhira kuchilango
chokhwima.
25. Ndipo ukawafunsa: "Ndani
adalenga thambo Ndi nthaka?"
Ndithu anena: "Ndi Mulungu."
Nena: "Kutamandidwa Konse
nkwa Mulungu." Koma ambiri a
iwo sadziwa.
26. Zonse zakumwamba ndi za
pansi, nza Mulungu. Ndithu,
Mulungu Ngwachikwanekwane,
Ngotamandidwa.
27. Ndipo ndithu, ngakhale
mitengo yonse Hi m'nthaka
ikadakhala zolembera, Ndipo
nyanja (nkukhala inki),
Ndikuionjezeranso (madzi ake) ndi
Nyanja zisanu ndi ziwiri, Mawu a
Mulungu sakadatha. Ndithu,
Mulungu Ngwamphamvu,
Wanzeru zakuya.
1 Ndime iyi ikufotokoza kuti Mawu a Mulungu ngochuluka. Mitengo yonse
padziko lapansi itakhala ngati mapensulo ndipo nyanja zonse padziko lapansi,
nkuwonjezanso nyanja zina, zikadakhala inki, zonse zikadatha koma Mawu a
Mulungu alipobe.
®
Surat 31. Luqman Juzu 21 875 Y > i£-\
T ) JUaJ tjj~*
28. Kulengedwa kwanu,
ngakhale Kuukitsidwa kwanu
m'manda sikuli Kanthu koma kuli
ngati (kulenga Kapena kuukitsa
kwa) munthu Mmodzi.(Palibe
chokanika kwa Mulungu).Ndithu,
Mulungu Ngwakumva Ngopenya
chilichonse.
29. Kodi suona (kuona
kolingalira) kuti Mulungu
amalowetsa nthawi ya usiku
Muusana, ndipo amalowetsa
nthawi Ya usana muusiku; ndipo
adagonjetsa Dzuwa ndi mwezi.
Chilichonse Chikuyenda
mwanthawi imene Idaikidwa?
Ndithu Mulungu akudziwa Zonse
zimene mukuchita.
30. Izi nchifukwa chakuti
Mulungu, lye Ngoona; ndipo
zomwe akuzipembedza Kusiya
lye, nzonama. Ndipo ndithu,
Mulungu ndiye Wotukuka Wamkulu.
31. Kodi suona kuti zombo
zikuyenda Panyanja mwamtendere
wa Mulungu Kuti akusonyezeni
zisonyezo (Zamtendere Wake)?
Ndithu M'zimenezo muli
zisonyezo kwa yense Wopirira,
wothokoza.
32. Ndipo mafunde onga
thambo Akawavindikira,
amampempha Mulungu
Modzipereka kwambiri. Koma
m^^%m%'M^c
<?9 "<{ 9 9 '*\ .
Surat31. Luqman Juzu21
876
n *>i
V > OUiJ Sjj-*
Akawapulumutsira kumtunda, ena
A iwo amachita zolungama.
(Koma Ena a iwo amakana
mtendere wa Mulungu).
Sangawakane mau Wathu Koma
yense wachinyengo wosathokoza.
33. E, inu anthu! Muopeni
Mbuye wanu (Potsatira malamulo
Ake ndi kusiya Zoletsedwa); ndipo
liopeni tsiku Limene tate
sadzathandiza mwana Wake,
ngakhalenso mwana Sadzathandiza
tate wake chilichonse.Ndithu,
lonjezo la Mulungu nloona;
Usakunyengeni moyo wadziko
lapansi, Ndiponso asakunyengeni
Mdyerekezi pa za Mulungu,
34. Ndithu, kudziwa kwa
nthawi (yakutha Kwa dziko) kuli
ndi Mulungu (yekha). lye
ndiamene amavumbwitsa mvula
(Nthawi imene wafuna); ndipo
Akudziwa zimene zili
m'ziberekero (Mwa zolengedwa
zake:zachimuna Kapena
zachikazi). Ndipo aliyense sadziwa
Chomwe apeze mawa; (chabwino
kapena Choipa); ndiponso
sadziwa aliyense Kuti ndi dziko liti
adzafera. Ndithu, Mulungu
ngodziwa ndiponso Wodzindikira
Mmene zinthu zilili.
Surat32. As-Sajdah Juzu21
877
T \ ij}r\ VY o*b^-Jl Ojj-j
SURAT AS-SAJDAH XXXII
Surayi idavumbulutsidwa pambuyo pa Sura ya Muuminina.
Ndipo ikufotokoza za kutsika kwa Qur'an ndi udindo wa
Mtumiki Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale naye);
kalengedwe ka thambo ndi nthaka; kalengedwe ka munthu
komwe nkosinthasintha; zoyankhula za otsutsa, kuuka ku imfa
ndi kuwayankha mtsutso ndi zizindikiro za chilengedwe zimene
zikusonyeza mphamvu za Mulungu zoposa, Amene sangalephere
kuukitsa anthu ku imfa.
Nkhani yaikulu m' Surayi ndikudzutsa anthu kuti apenye
zizindikiro za chilengedwe zimene zikusonyeza mphamvu za
Mulungu zoposa, Amene sangalephere kuukitsa anthu ku imfa.
Surat 32. As-Sajdah Juzu 21 878 t \ *>» r t 5u*~Ji a^
SuratAs-Sajdah XXXII
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1 . yi lif-Ldm-Mim.
2. Chivumbulutso cha Buku (la
Qur'an) Chilibe chikaiko mkati
mwake chochokera Kwa Mbuye
wa zolengedwa.
3. Kodi (Akuraishi
osakhulupirira), akuti: "Walipeka
yekha (ndi kumnamizira
Mulungu)?" Iyayi, ichi Nchoona
chimene (chavumbulutsidwa Kwa
iwe) uchokera kwa Mbuye wako
Kuti uwachenjeze anthu
ndichimenechi, Amene
sadawadzere mchenjezi Iwe
usadadze.Kuti aongoke (ndi
Kutsatira njira yolungama).
4. Mulungu ndi Yemwe
adalenga thambo Ndi nthaka ndi
zapakati pake M'masiku asanu ndi
limodzi; ndipo Adakhazikika pa
mpando Wake Wachifumu;
(kukhazikika kolingana Ndi
ulemerero Wake, kumene lye
Mwini wake akukudziwa). Inu
mulibe Mtetezi ngakhale
muomboli kupatula lye. Nanga
kodi bwanji simulingalira? 1
o^)t<^j)^U-
-^
" 99' 9' 9)4'\ luV "* ^
1 .M'ndime iyi Mulungu akutiuza kuti adalenga thambo ndi nthaka ndi zapakati
pake m'masiku asanu ndi limodzi. Komatu nthawi ya masiku amenewa, palibe
Surat32. As-Sajdah Juzu 21
879
t ^ frjA-i vy ojbtc^Ji djj--
5. (lye) akuyendetsa zinthu
(zonse) kumwamba Ndi pansi.
Ndipo kenako mapeto ake, (zonse)
Zimakwera kubwerera kwa lye, pa
tsiku Lolingana ndi zaka chikwi
chimodzi (Poyerekeza ndi zaka
zadziko lapansi)Zomwe inu
mumawerengera.
6. Ameneyo, ndi Mulungu
(Mwini kulenga ndi Kuyendetsa
zinthu), Wodziwa zobisika ndi
zoonekera; Mwini mphamvu
zoposa Wachisoni,
7. Yemwe adakonza bwino
chilengedwe Cha chilichonse.
Ndipo adayambitsa Chilengedwe
cha munthu kuchokera Kudongo.
8. Kenako adachita mbumba
yake kuti Ipangike kuchokera
m'madzi enieni Opandapake.
9. (Ndipo) kenako adamkonza
Ndi kumuuzira Mzimu Wake.
Ndipo adakulengerani Makutu,
maso ndi moyo. Kuthokoza
Kwanu mpang'ono ndithu,
10. Ndipo (otsutsa kuuka ku
imfa) akunena: "Kodi
tikadzatayika m'nthaka (ndi
Kusakanikirana ndi dothi),
Tidzalengedwanso mwatsopano?"
(Iyayi),Koma iwo sakhulupirira, za
kukumana Ndi Mbuye wawo.
^-vJ$£s$&*^
3±\zy&t£$^&&
,-V \J* ^ "'"-^
^J3J^> J H^
amene akudziwa tsatanetsatane wake koma Mulungu yekha. Choncho
tisaganizire kuti masikuwo adali olingana ndi masiku amoyo uno wadziko lapansi.
Surat 32. As-Sajdah Juzu 21
880
n *>i
rt dj^^Ji 5j_^»
11. Nena: "Adzachotsa mizimu
yanu Mngelo Wa imfa, yemwe
wapatsidwa udindo Umenewu pa
inu. Kenako Mudzabwezedwa kwa
Mbuye wanu."
12. Ndipo ukadawaona oipa
atazolikitsa mitu Yawo kwa
Mbuye wawo (uku akunena): "E,
Mbuye wathu! Taona, ndipo
tamva. Choncho tibwezeni.
Tikachita ntchito Zabwino. Ndithu,
tsopano tatsimikiza
(Kukhulupirira)."
13. Ndipo tikadafuna,
tikadampatsa munthu Aliyense
chiongoko chake (Momukakamiza
monga momwe Tidawachitira
angelo, koma munthu
Adapatsidwa mphamvu ndi ufulu
Wozisankhira chimene afuna;
chabwino Kapena choipa). Koma
Mawu Atsimikizika ochokera kwa
Ine: "Ndithu, ndizadzazitsa
Jahannama Ziwanda ndi anthu;
onse pamodzi (Amene ali oipa)."
14. "Choncho, lawani chifukwa
cha Kusalabadira kwanu
kukumana ndi Tsiku lanu ili.
Ifenso tikusiyani (ku Chilango
monga ngati takuiwalani). Tero
Lawani chilango chamuyaya,
Chifukwa cha zomwe munkachita."
15. Ndithu, amene
akukhulupirira aya Zathu,
£8te$*9$&$gX%&
®6y^y &»M&
«&
&&Mm%k&$2i
\j>>*>&
Surat32. As-Sajdah Juzu 21 881 ^ *>' rr 5o*-Ji 3 j^
ndiamene akuti pamene
Akulangizidwa ndi ayazo, amagwa
Kusujudu ndi kulemekeza Mbuye
Wawo pamodzi ndi kumthokoza.
Ndipo iwo sadzitukumula.
16. Nthiti zawo zimalekana ndi
malo ogona (Usiku), chifukwa
chopembedza Mbuye Wawo,
poopa chilango chamoto ndi
Kulakalaka munda wamtendere.
Ndipo Amapereka (zakati ndi
sadaka) M'zimene tawapatsa.
17. Mzimu uliwonse sudziwa
zimene Aubisira zotonthoza diso
(zosangalatsa Moyo ku munda
wamtendere) monga Mphoto
pazimene unkachita.
18. Kodi Msilamu wokwanira
angafanane Ndi wotuluka
m'chilamulo cha Mulungu?
Sangafanane.
19. Kwa amene akhulupirira ndi
kumachita Zabwino, adzalandira
minda Yokhalamo yokongola,
monga Phwando lawo pazimene
ankachita.
20. Koma kwa amene adachita
zoipa Potuluka m'chilamulo cha
Mulungu, Malo awo ndi kumoto.
Nthawi iliyonse Akafuna
kutulukamo,Azikabwezedwamo
ndipo Azidzauzidwa: "Lawani
chilango Chamoto, chomwe
munkachitsutsa."
^i^^ij^jl^
\V'<i'\
®u&\}w$&m
Surat32. As-Sajdah Juzu21
882
V \ frji-l fY o*t*~Jl djj--
21. Ndipo ndithudi, tiwalawitsa
chilango Chocheperapo (padziko
lapansi) Chisanafike chilango
chachikulu (cha Tsiku lomaliza),
kuti atembenuke, (Alape).
22. Kodi ndani wachinyengo
kwambiri, Woposa yemwe
akukumbutsidwa aya Za Mbuye
wake, kenako nkuzikana? Ndithu,
Ife, tidzawabwezera zoipa Anthu
oipa.
23. Ndipo ndithu, Musa
tidampatsa Buku . Choncho
usakhale ndi chikaiko pa
Zakukumana Naye (Mulungu).
Ndipo Tidalichita (Bukulo)
kukhala Chiongoko cha ana a
Israeli.
24. Ndipo ena mwa iwo
tidawachita Kukhala atsogoleri
oongola (anthu) Mwa lamulo lathu,
pamene adapirira; Ndipo adali
kuvomereza motsimikiza Aya Zathu.
25. Ndithudi Mbuye wako ndi
Yemwe Adzaweruza pakati pawo
tsiku Lomalizira pazimene
amakangana.
26. Kodi sizidadziwike kwa iwo
kuti Ndimibadwo ingati imene
tidaiononga Patsogolo pawo;
(chikhalirecho iwo) Akudutsa
mokhala mwawo? Ndithu,
M'zimenezo, muli
zizindikiro.Kodi sakumva?
5J*i^i(!s£i<i&A
$
Surat32. As-Sajdah Juzu 21 I 883 ^ *>' TY sa^-JUjj^
27. Kodi sakuona kuti
timapereka madzi Kunthaka
youma; ndipo ndi madziwo
Tikumeretsa mmera umene ziweto
Zawo zimadya ndi iwo omwe;
Kodi sakuona?
28. Ndipo akunena:
"Kulamulidwa Kumeneku (kwa
tsiku lachimaliziro) Kudzachitika
liti, Ngati mukunenadi zoona?"
29. Nena: "Tsiku
lachiweruzolo, amene
Sadakhulupirire, chikhulupiriro
chawo Sichidzawathandiza. Ndipo
Sadzapatsidwa nthawi
yoyembekezera (Kuti mizimu
yawo isachoke ayambe
Akhulupirira kaye, mngero wa
imfa Akadzawadzera?)."
30. Choncho apatuke; ndipo
yembekezera (Zimene Mulungu
wakulonjeza). Ndithu, nawonso
akuyembekezera (Zimene
Mulungu wawalonjeza).
^^ptiSJ&s- <J^^
©fci L '
Surat33. Al-Ahzab Juzu 21
884
t \ *jk-\ rr ^\y*t\ oji-
Sura ya Ahzab ndiimodzi mwa zimene zidavumbulutsidwa ku
Madina. Ikufotokoza mbali ina ya malamulo a mbado wa mtundu
wa Chisilamu, monga momwe zilili sura zovumbulutsidwa ku
Madina.
Surayi yafotokoza zamoyo wa Asilamu munthu
payekhapayekha, ndi pagulu, makamaka pazinthu zapabanja.
Ndipo yakhazikitsa malamulo odzetsa mtendere ndi chisangalalo
ku mtundu. Ndipo yathetsa zizolowezi zina zomwe ankachita
anthu akale, monga mwana wobala wina nkumuyesa ngati wako
chifukwa chomulera, komanso kumuyesa mkazi wako ngati
mayi wako. Amakhulupiriranso kuti mwa munthu muli mitima
iwiri.
Titha kufotokoza mwachidule mitu ikuluikulu yomwe ili
m' suramu motere : -
l)Kuongolera kumiyambo yofunika kuitsata m'Chisilamu
2)Kufotokoza za Malamulo a Mulungu
3)Kufotokoza nkhani ya nkhondo ziwiri: ya Ahzab ndi ya
Ban kuraidhwa
M'mutu woyambau, mwadza nkhani yofotokoza miyambo
yokhalirana wina ndi mnzake pagulu, monga miyambo ya
pachisangalalo cha ukwati, ndi mkazi kudziphimba thupi lonse,
ndi kuti asayendeyende m'misewu uku atadzikongoletsa ndi
cholinga choti akaonedwe ndi amuna. Ndi Miyambo
yokhalirana ndi Mtumiki wa Mulungu, Muhammad (madalitso
ndi mtendere zikhale naye) ndi kumlemekeza. Ndi miyambo
yofunika kuitsata pokhalirana pafuko.
Tsono m'mutu wachiwiri, mwadza nkhani ya malamulo
oletsa kumuyesa mkazi monga mayi wako, ndi mwana
womulera chabe monga mwana wako, ndi woyenera kulandira
chuma chamasiye, ndi chilolezo chokwatira mkazi amene
Surat33. Al-Ahzab Juzu 21
885
y > ij*r\ rr i~>\yH\ «;>-»
wasiyidwa ndi mwana yemwe udali kumlera chabe, ndi zamitala
ya Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) ndi zolinga
za mitalayo. Ndiponso lamulo lopempherera madalitso Mtumiki
(madalitso ndi mtendere zikhale naye,) ndi malamulonso ena
omwe adakhazikitsidwa.
Tsono m'mutu wachitatu, Surayi ya fotokoza mwatsatanetsatane
za nkhondo ya Khandaki yomwe imatchedwanso nkhondo ya
Ahzab. Ndipo yapereka chithunzi chakuya kwambiri pachimvano
chamagulu ambiri a anthu pochitira upandu Asilamu.
Ndipo Surayi yavundukula zachinsinsi cha Amunafikina ndi
kuchenjeza zakutsatira njira zawo zachinyengo ndi zokaikitsa.
Ndipo yatalikitsa nkhani yawo kuyambira pachiyambi cha
Surayi ndi kumalekezero ake kufikira siidawasiyire chobisika
chilichonse.
Ndipo yakumbutsa Asilamu za mtendere waukulu wa
Mulungu powabweza m'mbuyo adani awo popanda chopindula
adani wo, pamene Mulungu adawalimbikitsa Asilamu ndi angero
ndi mphepo ya mkuntho imene idaononga katundu wa adani.
Surayi yafokozanso zankhondo ya Bani Kuraidhwa ndi
kuswa kwa Ayuda mapangano omwe adalipo pakati pawo ndi
Mtumiki Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale naye).
Surayi ikutchedwa Ahzab chifukwa cha kuti mafuko onse a
Arabu ndi Ayuda, adasonkhana ndi kumvana kuthira nkhondo
Asilamu monga dzanja limodzi.
Surat33. AI-Ahzab Juzu21
886
y \ frjA-i rr *->\yH\ *;>-
Surat AUAhzab XXXIII
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. E, iwe Mneneri! Pitiriza
kuopa Mulungu,ndipo usamvere
Osakhulupirira ndi achiphamaso.
Ndithu, Mulungu Ngodziwa
kwambiri; Wanzeru zakuya
(m'zoyankhula Ndi m'zochita
Zake). 1
2. Ndipo tsata zimene
zikuvumbulutsidwa kwa iwe
kuchokera kwa Mbuye wako
(Pozigwiritsa ntchito). Ndithu,
Mulungu Ngodziwa zonse zimene
mukuchita.
3. Ndipo yadzamira kwa
Mulungu; ndipo Mulungu
akukwana kukhala Msungi ndi
Mtetezi (wako).
4. Mulungu sadaike m'chifuwa
cha Munthu mitima iwiri. Ndipo
sadachite Akazi anu amene
mukuwayesa ena Mwa iwo monga
wm^&m
^ I
Q^t^t^U-
~&
4$&\$&\&jz
LSura iyi ikutchedwa Sura ya Ahzab kutanthauza kuti namtindi wa anthu.
Zimenezi zidali chonchi kuti pamene Chisilamu chimafala mu Mzinda wa
Madina Munawara momwe mumakhalanso Ayuda, adachita nsanje yaikulu
Ayudawo. Ndipo akuluakulu awo adaganiza zopita ku Makka kukakopa Arabu
akumeneko kuti athandizane kuthira nkhondo Asilamu. Choncho Arabu a ku
Makka adauza mitundu yonse yopembedza mafano kuti akamthire nkhondo
Muhammad(SAW) ndi kuthetseratu chipembedzo cha Chisilamu. Tero
adagwirizana ndipo adauzinga Mzinda wa Madina mbali zonse. Koma Mulungu
adatumiza angero ndi chimphepo chamkuntho chomwe chidamwazamwaza
katundu wawo. Pachifukwa ichi, onse adathawa.
Surat 33. Al-Ahzab Juzu 21 I 887 I * > *& TT ^>\^H\ &;>-
amayi anu, kukhala Mayi anu
enieni. Ndipo Sadachite ana anu
ongowalera kukhala Ana anu
enieni (monga inu
Mukuwatchulira). Zimenezo ndi
zolankhula Zanu za m'milomo
mwanu chabe.Koma Mulungu
akunena choona; lye Akuongolera
ku njira yoongoka.
5. Aitaneni ndi maina a atate
awo. Kutero Ndichilungamo kwa
Mulungu. Koma Ngati
simukuwadziwa atate awo,
(Aitaneni ngati) abale anu
Pachipembedzo; ndiponso ndi
anzanu. Palibe uchimo kwa inu pa
zimene Mwazichita molakwitsa
(mosazindikira). Koma (pali
uchimo) pazimene mitima Yanu
yachita mwadala. Ndipo Mulungu
Ngokhululuka kwabasi,
Ngwachisoni.
6. Mneneri ngofunika kwambiri
kwa Okhulupirira kuposa moyo
wawo,(Matupi awo ndi chuma
chawo); ndipo Akazi ake ndi
amayi awo (amayi a Asilamu;
nkoletsedwa kuwakwatira
Pambuyo pa imfa yake). Ndipo
achibale Pakati pawo ngoyenera
(kulandira Zamasiye pamalamulo
a) m'Buku la Mulungu kuposa
Asilamu ena Ngakhalenso
Amuhajirina (amene Adasamuka
ku Makka kupita ku Madina
Siirat33. Al-Ahzab Juzu 21
888
r \ *>» rr v 1 ^ 1 s^
chifukwa cha chipembedzo Cha
Chisilamu). Koma ngati mutachita
Zabwino kwa anzanu (sikuipa). Izi
zidalembedwa kale m'buku. 1
7. Ndipo (akumbutse) pamene
tidalandira Kuchokera kwa
Aneneri onse Pangano lawo. Ndi
kwa iwe, ndi kwa Nuhi, Ibrahim,
Musa, ndi Isa mwana wa
Mariyamu. Ndipo tidatenga kwa
iwo pangano La mphamvu (kuti
adzafikitsa uthenga Wa Mulungu
kwa anthu ndi kuitanira Anthu ku
chipembedzo cha Mulungu).
8. Kuti (Mulungu) adzafunse
(Aneneri) oona (Tsiku la
chimaliziro) pazimene adanena
(Kwa anthu awo zakufikitsa uthenga
Woonadi kwa iwo). Ndipo Mulungu
wawakonzera (Osakhulupirira)
chilango chopweteka.
9. E, inu amene
mwakhulupirira! Kumbukani
mtendere wa Mulungu Umene uli
pa inu, pamene adakudzerani Magulu
ankhondo. Ndipo Tidawatumizira
mphepo ndi magulu A nkhondo (a
angero) amene Simudawaone.
Ndipo Mulungu Akuona (zonse)
zimene mukuchita. 2
ffijfc£*4&vfeb&\$%l
®$%ffi
Aya iyi ikufotokoza zakuletsedwa kukwatira akazi a Mtumiki (SAW), mwini
wake atafa chifukwa choti akazi a Mtumiki(SAW) ndiamayi a Asilamu onse
2 Pamene Mtumiki(SAW) adali mu mzinda wa Madina adamzinga magulu
ambiri ankhondo omwe ena a iwo adali amtundu wa Ghatfan, Ayuda a
Chikuraidha ndi Ayuda a Bani Nadhir. Adali ochuluka 12,000.
Surat 33. Al-Ahzab Juzu 21 I 889 I t \ *>i YT >->\y*H\ 3jj--
10. Pamene adakudzerani
chakumtunda Kwanu, ndi kunsi
kwanu (kumtunda Kwa dambo ndi
kumunsi kwake), Pamene maso
adangoti tong'oo Cham'mbali
ndipo mitima idafika Kum'mero
(chifukwa chamantha ndi
Kunjenjemera) uku
mukumganizira Mulungu
maganizo osiyanasiyana.
11. Panthawi imeneyo Asilamu
adayesedwaMayeso aakulu.
Adanj enj emeretsedwa
Kunjenjemera kwambiri.
12. Ndipo pamene ankanena
Amunafikuna (Achinyengo) ndi
omwe m' mitima Mwawo muli
matenda: "Palibe chomwe
Adatilonjeza Mulungu ndi
Mtumiki Wake koma chinyengo
basi."
13. Ndipo pamene gulu lina
mwa iwo lidanena: "E, inu nzika
za mu Yathiriba (Madina)! Palibe
njira kwa inu (yokhalira
pankhondo Yogonjayi). Choncho
bwererani (kunyumba Zanu;
Pamene Mtumiki (SAW) adamva za kudza kwawo adakumba chidzenje
chachikulu kumbali ina ya Mzinda wa Madina yomwe adaiganizira kuti adani
angalowereko. Izi zidachitika potsatira malangizo a Salman Farisiyu. Kenako
Mtumiki(SAW) adatuluka ndi ankhondo ake okwana 3,000 nakamanga
mahema awo pafupi ndi chidzenjecho moyang'anizana ndi adani awo.Asilamu
adagwidwa ndi mantha aakulu kotero kuti Asilamu achiphamaso adayamba
kuthawa. Koma pompo Mulungu adatumizira adaniwo chimphepo ndi magulu
ankhondo a angero omwe sadathe kuwaona ndi maso awo, nawabalalitsa
adaniwo ndi kuwatayira katundu wawo kutali.
Surat 33. Al-Ahzab Juzu 21
890
y \ tj±\ rr ^\y*H\ ojj--
msiyeni Muhammad alimbane
yekha Ndi adani ake)". Ndipo gulu
lina lankhondo Lochokera mwa
iwo limapempha chilolezo Kwa
Mneneri(SAW) (Chobwerera ku
Madina) ponena (kuti): "Ndithu
nyumba zathu nzamaliseche
(Zopanda chitetezo)". Koma izo
Sizamaliseche. Sakufuna china,
koma Kuthawabasi.
14. Ndipo akadawalowera
(magulu ankhondo A adaniwo),
mbali zonse (za Mzindawo),
Kenako nkupemphedwa kuti
atuluke M'Chisilamu ndi
kumenyana ndi Asilamu,
Akadachita zimenezo; ndipo
Sakadayembekezera koma nthawi
yochepa Basi.
15. Ndipo ndithu, (awa amene
adathawa Pabwalo lankhondo),
adali atamulonjeza Kale Mulungu
(kuti iwo) sadzatembenuza Misana
(kuthawa). Ndipo lonjezo la
Mulungu nlofunsidwa. (Choncho
Iwo adzafunsidwa pazomwe
adalonjeza Kwa Mulungu).
16. Nena: "Kuthawa
sikungakuthandizeni Ngati
mukuthawa imfa kapena
Kuphedwa; choncho (kuthawa
Kwanuku) simusangalatsidwa
(nako) Koma pang'ono basi.
(Kenako Ikatha nthawi yamoyo
wanu, mukufa)".
©!5& !^^wl s IS^^j
Surat 33. Al-Ahzab Juzu 21
891
t y frjA-i rr ^\y*i\ *^
17. Nena: "Kodi ndani amene
Angakutetezeni kwa Mulungu,
Ngati atafuna kukuchitirani
choipa; Kapena atafuna
kukuchitirani chifundo?" Ndipo
sadzapeza mthandizi ndi mtetezi
Kupatula Mulungu.
18. Ndithu, Mulungu
akuwadziwa amene Akudziletsa
mwa inu (kupita Kunkhondo
pamodzi ndi Mtumiki (SAW), ndi
Kuletsanso anthu ena). Ndi amene
Akuuza abale awo:"Bwerani kwa
ife; (M'thaweni
Muhammad {SAW})." Ndiponso
Sapita kunkhondo koma pang'ono
Pokha.
19. Okuchitirani inu umbombo
(pachikondiNdi pachifundo;
sakufunirani zabwino). Koma
mantha akadza uwaona
Akukuyang'ana, uku maso awo
Akutembenuka
(mophethiraphethira) Monga a
amene wakomoledwa ndi Imfa.
Koma mantha akachoka,
Akukupatsani masautso ndi
malirime Awo akuthwa; mbombo
pa chabwino Chilichonse. Iwowo
sadakhulupirire Ndipo choncho
Mulungu wagwetsa Malipiro a
zochita zawo. Zimenezo
Nzosavuta kwa Mulungu.
20. (Kufikira tsopano chifukwa
cha mantha Awo) akuganiza kuti
'\C 9 i'e\**< \' 9 \'X?sS\ '#'*'+
^$S^<&®G§&
Surat33. Al-Ahzab Juzu 21
892
y \ *>t rr s-^ij^Vi 5jj-
magulu ankhondo (Adani)
sadapitebe; ndipo magulu Amenewo
akadadzanso, akadalakalaka
Akadakhala kuchipululu pamodzi
ndi Anthu am'chipululu ndi kuti
Azikangofunsa za nkhani Zanu.
Akadakhala pamodzi ndi inu
Sadakamenyana (ndi adani) koma
Pang'ono pokha. 1
21. Ndithu, muli nacho
chitsanzo chabwino Mwa Mthenga
wa Mulungu (M'kudzipereka
kwake ndi khama Lake pa njira ya
Mulungu, ndi kupirira Kwake ndi
masautso) kwa yemwe Akuopa
Mulungu ndi tsiku Lachimaliziro,
namatchula Mulungu kwambiri.
22. Ndipo pamene Asilamu
adaona Magulu a nkhondo (a
adani atawazinga Mbali
zonse),adati: "Ichi ndichimene
Mulungu ndi Mtumiki Wake
Adatilonjeza (kuti tidzapeza
masautso, Kenako nkupambana),
ndipo Mulungu ndi Mtumiki Wake
adanena zoona". Ndipo (ichi)
sichidawaonjezere china, Koma
chikhulupiriro (mwa Mulungu)
Ndi kudzipereka.
fan?
Kuyambira ndime 12 mpaka 20, Mulungu akufotokoza makhalidwe a anthu
ena amene adangolowa m'Chisilamu ndi lirime lokha pomwe mitima yawo
siidakhulupirire. Nthawi zambiri ankamchitira Mtumiki (SAW) zachinyengo.
Mtumiki (SAW) akalamula lamulo loti akalimbane ndi adani achipembedzo
cha Chisilamu, iwo amagwetsa ulesi anthu kuti asapite kunkhondoko. Nthawi
zambiri samawafunira Asilamu zabwino. Akangouzidwa kuti tiyeni kunkhondo,
amagwidwa ndi mantha.
Surat33. Al-Ahzab Juzu 21
893
t^ *>i
rr ^yy 5jj--
23. Mwa okhulupirira alipo
amuna ena Amene adakwaniritsa
zomwe Adamlonjeza Mulungu
(kuti Sadzathawa pankhondo
pamodzi ndi Mtumiki{SAW}), ena
mwa iwo adamaliza Moyo wawo
(nakwaniritsa Lonjezo lawo pofera
panjira ya Mulungu). Ndipo ena
mwa iwo Akuyembekezerabe
(kufera panjira ya Mulungu). Ndipo
sadasinthe konse (Lonjezo lawo). 1
24. Kuti Mulungu awalipire
oona chifukwa Cha kuona kwawo;
ndi kuti awalange Achiphamaso
(Amunafikina) ngati Atafuna,
kapena kuwalandira kulapa
Kwawo (ngati atalapa). Ndithu,
Mulungu Ngokhululuka kwabasi
Ngwachisoni.
25. Ndipo Mulungu
adawabweza amene
Sadakhulupirire uku ali odzazidwa
£
1 Imamu Ibnu Jarir Taburiyu adalemba m'buku lake kuti Anasi Bun Malik
adati:- M'bale wa bambo anga, Anasi bun Nadhari sadakhale nawo
pankhondo ya Badri, ndipo adati: "Sindidakhale pamodzi ndi Mtumiki pankhondo
yoyamba. Ngati Mulungu atandifikitsa pankhondo ina Mulungu adzaona
zimene ndidzachita pomenya nkhondo modzipereka." Pa tsiku lankhondo ya
Uhud, pamene Asilamu adabalalikana kuthawa ndipo iye adati:- "O.Ambuye
Mulungu! Ine ndikudzipatula kuzomwe achita awa, osakhulupirira. Ndiponso
ndikudandaula mzimene achita awa, Asilamu amene athawa." Kenako
adayenda ndi lupanga lake akumana ndi Saad bun Muadhi, nati: "E, iwe
Saad! Ine ndikumva fungo la ku Munda wa mtendere pafupi ndi phiri ili la
Uhud." Kenako adachita nkhondo kufikira adaphedwa. Ndipo Saad adati: "E,
iwe Mtumiki wa Mulungu! Sindinathe kuchita chimene iye adachita." Anasi bun
Malik adati: Tidampeza ali m'gulu lophedwa uku ali ndi mabala okwanira 80,
ena otemedwa ndi malupanga, ndipo ena olasidwa ndi mikondo ndi mipaliro.
Sitidamzindikire kufikira pamene adadza mlongo wake naamzindikira
pakupyolera m'nsonga za zala zake." Ndipo Anasi adatinso: "Tidali
kukambirana kuti ndime iyi ikukamba za iye".
Surat33. Al-Ahzab Juzu21
894
t \ ftjA-» rr ^yy «j>-<
ndi Mkwiyo m'mitima mwawo;
sadapeze Chabwino; (sadagonjetse
Asilamu ndi Kupeza zimene
ankaziyembekezera Monga zotola
zapankhondo). Ndipo Mulungu
adawakwaniritsira
AsilamuNkhondo (powatumizira
adani mphepo Yamkuntho ndi
angero). Ndipo, Mulungu
Ngwamphamvu, Ngopambana,
(Sapambanidwa ndi chilichonse).
26. Ndipo adawatsitsa
m'malinga mwawo Amene
adathandiza adaniwo mwa Anthu a
Buku, (Ayuda). Ndipo adathira
Mantha m'mitima mwawo. Ena
Mumawapha; ndipo ena
mumawagwira. ]
27. Ndipo adakupatsani dziko
lawo, Nyumba zawo, chuma
chawo, ndi Nthaka imene
simudaipondepo . Mulungu
Ngokhoza chilichonse.
28. E, iwe Mneneri! Nena kwa
akazi ako (M'njirayowalangiza):
"Ngati mufuna Moyo wadziko
lapansi ndi zosangalatsa Zake (ine
ndilibe zosangalatsa za M'dziko,
mm&
L if? 4.
.Awa ndi Ayuda amene adasakanikirana ndi osakhulupirira (akafiri) a
Chiarabu ochokera mumtundu wa Banu Quraidhwa omwe adali ndi
mapangano ndi Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) okhalirana
mwamtendere. Koma pamene adaswa mapangano pothandizana ndi adani a
Mtumiki kuthira nkhondo Asilamu Mtumiki Muhammad (madalitso ndi
mtendere zikhale naye) adawapitira ku malinga awo. Ndipo ena adawapha,
pomwe ena adawagwira monga akaidi apankhondo.
Siirat33. Al-Ahzab Juzu 22
895
1 1 >jk\ rr <->\jrH\ 5jj~-
ndipo sindingakukakamizeni Kuti
mukhale ndi ine mumoyo
Waumphawi; ngati mufuna)
bwerani Ndikupatsani cholekanira,
Chokusangalatsani, kenako
ndikusiyeni Kusiyana kwabwino
(kopanda Masautso).
29. Ndipo ngati mukufuna
Mulungu ndi Mtumiki Wake, ndi
nyumba yomaliza, ndithu Mulungu
wawakonzera ochita zabwino Mwa
inu malipiro aakulu."
30. E, inu akazi a Mneneri!
Amene achite Choipa choonekera
mwa inu, Amuonjezera chilango
kawiri; ndipo Zimenezi nzosavuta
kwa Mulungu 1
31. Koma yense mwa inu
amene amvere Mulungu ndi
Mneneri Wake, ndi Kumachita
zabwino ,timpatsa malipiro Ake
kawiri ndi kumkonzera Riziki
laulemu.
32. E, inu akazi a Mneneri! Inu
simuli Monga mmodzi wa akazi
ena (omwe Siakazi a Mtumiki,
paulemerero) ngati Muopa
Mu aya imeneyi, akazi a Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye)
akuuzidwa kuti iwo akachimwa, Mulungu adzawalanga chilango chachikulu
kuposa momwe akadalangidwira akazi ena omwe sali akazi a Mtumiki
(madalitso ndi mtendere zikhale naye). Izi nchifukwa chakuti, iwo ndi atsogeleri;
chilichonse chomwe iwo achita, choipa kapena chabwino, chidzatsatidwa ndi
ena. Akachita chabwino, Mulungu adzawapatsa malipiro aakulu. Ndipo
akachita choipa, adzawalanga ndi chilango chachikulu. Choncho aliyense
amene ndi mtsogoleri, aonetsetse kuti akuchita zolungama zokhazokha.
Surat 33. Al-Ahzab Juzu 22
896
y y *>» rr <->\yH\ Sjj-
Mulungu. Choncho Musalobodole
mawu (mowakometsa
Poyankhulana ndi amuna,) kuti
Asalakelake (kuchita zoipa ndi
inu) Yemwe mumtima mwake
muli matenda (Achiwerewere).
Koma nenani Zonena zabwino.
33. Ndipo khalani m'nyumba
zanu, ndipo Musadzionetsere (kwa
amuna) uku Mutadzikongoletsa
monga mmene Ankaonetsera
zokongoletsa zawo (Akazi) a
m'nthawi ya umbuli wakale.
Ndipo pempherani swala
moyenera; Perekani zakati;
mverani Mulungu ndi Mtumiki
Wake. Mulungu afuna
Kukuchotserani uve. E, inu,
akunyumba (Ya Mneneri!) Ndi
kuti akuyeretsani ndithu.
34. Ndipo lowezani pamtima
zimene Zikunenedwa m'nyumba
zanu; ndime Za Mawu a Mulungu
ndi (zonena za Mtumiki) zanzeru.
Ndithu, Mulungu Ngodziwa zinthu
zobisika Kwambiri, ndi zapoyera.
35. Ndithu, Asilamu achimuna
ogonjera Mulungu mokwanira, ndi
Asilamu Achikazi ogonjera
Mulungu mokwanira; Okhulupirira
achimuna ndi okhulupirira
Achikazi; omvera achimuna ndi
omvera Achikazi; oona achimuna
ndi oona Achikazi; opirira
achimuna ndi opirira Achikazi;
Surat 33. AI-Ahzab Juzu 22
897
r r *>i rr ^y^ oj>-
odzichepetsa achimuna ndi
Odzichepetsa achikazi; opereka
sadaka Achimuna ndi opereka
sadaka achikazi; Osala achimuna
ndi osala achikazi; Osunga
umaliseche wawo (kuchiwerewere)
Achimuna ndi osunga umaliseche
wawo Achikazi; otamanda
Mulungu kwambiri Achimuna ndi
otamanda Mulungu Kwambiri
achikazi, Mulungu Wawakonzera
chikhululuko ndi Malipiro aakulu.
36. Ndipo sikoyenera kwa
wokhulupirira Wachimuna ndi
wokhulupirira wachikazi, Mulungu
ndi Mtumiki Wake akalamula
Chinthu, iwo kukhala ndi chifuniro
Pazinthu zawo. Ndipo amene
akunyoza Mulungu ndi Mtumiki
Wake, ndithu, Wasokera; kusokera
koonekera. 1
37. Ndipo (kumbuka) pamene
udamuuza Yemwe Mulungu
adampatsa mtendere
(Pomuongolera ku Chisilamu,
ndipo) Iwenso udampatsa
mtendere (pomulera Ndi kumpatsa
ufulu,yemwe ndi Zaid Bun
Haritha, udati kwa iye):
"Gwirizana ndi mkazi wako, ndipo
©
1 Ndime iyi ikunenetsa kuti sikoyenera kwa Msilamu kutsata maganizo ake
pachlnthu chimene Mulungu ndi Mtumiki walamulapo lamulo, koma afunika
kutsatira lamulo la Mulungu ndi Mtumiki, ndipo asakhale ndi chifuniro pa zinthu
zomwe nza chipembedzo koma agonjere zimene Mulungu walamula ndi Mtumiki
Wake. Kunyoza lamulo la Mulungu ndi Mtumiki kumachititsa kuti munthu atayike.
Surat 33. Al-Ahzab Juzu 22
898
tt*>i rr oi^idj^
Opa Mulungu." Ukubisa mumtima
Mwako chimene Mulungu afuna
Kuchisonyeza poyera (chomwe ndi
kuti Mulungu akulamula
kumkwatira mkazi Ameneyo
akamuleka Zaid Bun Haritha Kuti
chichoke chizolowezi choti mwana
Wongomulera chabe nkumuyesa
Mwana wako weniweni). Ndipo
ukuopa Anthu (kuti akudzudzula
pazimenezo), Pomwe woyenera
kumuopa ndi Mulungu. Choncho
pamene Zaid adamaliza
Chilakolako chake pa mkazi
ameneyo, Tidakukwatitsa iwe kuti
pasakhale Masautso pa Asilamu
pokwatira akazi A ana awo
akungowalera chabe ngati
(Anawo) atamaliza zilakolako
zawo pa Akaziwo, ndipo lamulo la
Mulungu Ndilochitika,(palibe
chingalepheretse Kuti lisachitike). 1
38. Palibe tchimo pa Mneneri
pa zimene Mulungu wamulamula.
Chimenechi Ndichizolowezi cha
Mulungu (njira ya Mulungu) pa
amene adanka kale. Ndipo Lamulo
la Mulungu ndi chiweruzo
Polamula chinthu kuti chichitike kapena chisachitike, pafunika kuti iwe
wolamula ukhale woyamba kutsata malamulowo. Ngati sutero, ndiye kuti
malamulo akowo sangakhale ndi mphamvu. Mu ndime iyi ,muli lolezo
lakumkwatira mkazi yemwe wasiyidwa ukwati ndi mwana yemwe
adangoleredwa chabe ndi munthu amene amatcha mwanayo kuti ndi mwana
wake chifukwa chomulera. Kalelo zoterezi sizimaloledwa. Choncho Mtumiki
(madalitso ndi mtendere zikhale naye) adauzidwa kuti achite iye mwini
zimenezi pofuna kuthetsa chikhalidwecho.
Surat 33. AI-Ahzab Juzu 22
899
y t fr>» rr *->\y*H\ ijy*
(Chomwe) chidaweruzidwa.
(Ndipo sichisinthidwa). 1
39. (Aneneri) amene amafikitsa
uthenga wa Mulungu (kwa anthu)
uku akumuopa lye, ndipo
samamuopa aliyense koma
Mulungu (yekha). Ndipo Mulungu
Akukwana kukhala wowerengera
(Zochita za akapolo Ake).
40. Muhammad (SAW) sali tate
wa aliyense mwa Amuna anu,
koma iye ndi Mtumiki wa
Mulungu, ndiponso wotsiriza mwa
Aneneri. Ndipo Mulungu
Ngodziwa Chilichonse.
41. E, inu amene
mwakhulupirira! Tamandani
Mulungu; kumtamanda Kwambiri;
42. Ndipo mulemekezeni
m'mawa ndi madzulo.
&Q&&£ffi&&%&
&M&*j&3$&
V ( j»»,
©1
e5M5tS*>¥/
1 Ndime iyi ikumuuza Mtumiki (SAW) kuti palibe vuto pa iye ngakhale tchimo
kapena kudzudzulidwa pachomwe Mulungu wamulamula kuchichita monga
kukwatira akazi ambiri. Ayuda amamunyoza ndi kumudzudzula chifukwa
chokwatira akazi ambiri. Koma Mulungu adawayankha ndi mawu ake oti, "Iyi
ndi njira ya Mulungu yomwe idalipo pa Aneneri akale! Daudi adakwatira akazi
100. Ndipo Sulaimani akazi 300.
2 Ndime iyi ikumuuza Mtumiki kuti amene adamulamula kuti awatsanzire
pazimene ankachita ndi iwo amene ankafikitsa uthenga wa Mulungu kwa
anthu, ndipo samaopa kudzudzulidwa ndi aliyense pachomwe Mulungu
wawalamula kuchita, koma ankangoopa Mulungu yekha. Choncho nawenso
tsanzira khalidwe lawo ndi kuopa Mulungu yekha.
3 ("Khataman Nabiyyina) "Mneneri wotsirizira" tanthauzo lake ndi kuti Mtumiki
Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale naye) ndimneneri womalizira;
palibe mneneri wina pambuyo pake mpaka kutha kwadziko lapansi. Aya
imeneyi ikutsutsa ndi zonena za Akadiyani omwe akumutcha mtsogoleri wawo
kuti ndi mneneri.
4 Mulungu wasankha nthawi ziwiri kuti zikhale zochulukitsa kumtamanda ndi
kumulemekeza chifukwa chakuti zimenezi ndi nthawi zabwino zimene angelo
amatsika kuchokera kumwamba.
Surat 33, Al-Ahzab Juzu 22
900
t y ^>i rr ^\j^H\ djj-
43. lye ndi Amene
akukuchitirani chifundo(Ndi
kukufunirani zabwino) nawonso
Angero Ake (akukupemphererani
kwa Mulungu) kuti akutulutseni
mumdima Ndi kukuikani
m'kuunika. Ndipo (lye)
Ngwachisoni kwa Asilamu.
44. Kulonjerana kwawo tsiku
lokumana Naye, kudzakhala koti:
"Mtendere!", Ndipo wawakonzera
malipiro a ulemu.
45. E, iwe Mneneri (wa
Mulungu)! Ndithu, Ife takutuma
(kuti ukhale) mboni (pa Anthu ako
ndi pamibadwo yonse).Wonena
Nkhani zabwino (kwa oopa
Mulungu), Ndi mchenjezi (kwa
onyoza Mulungu).
46. Ndi kuti ukhale woitanira
(anthu) kwa Mulungu kupyolera
m'chifuniro Chake. Ndi (kutinso
ukhale) nyali younikira (Anthu).
47. Ndipo auze nkhani yabwino
okhulupirira Kuti iwo ali ndi
zabwino zazikulu kwa Mulungu.
48. Ndipo usawamvere
osakhulupirira ndi Achiphamaso
(pazimene akufuna kuti
Uwapeputsire malamulo a
Mulungu), Usalabadire masautso
awo, ndipo tsamira Kwa Mulungu.
Ndipo Mulungu Akukwanira
kukhala Mtetezi.
eg^^f&MW
Surat 33. Al-Ahzab Juzu 22
901
y v t>i rr ^\y-H\ *>^>
49. E, inu amene
mwakhulupirira! Mukakwatira
akazi okhulupirira, kenako
Ndikulekana nawo
musadawakhudze, Inu mulibe
chiwerengero cha 'edda' Pa iwo
choti nkuchiwerengera.
Asangalatseni powapatsa
cholekanira, Siyananawoni;
kusiyana kwabwino.
50. E, iwe Mtumiki! Ndithu Ife
takuloleza (Kukhala nawo
pamodzi) akazi ako Amene
wawapatsa chiwongo chawo, Ndi
chimene dzanja lako lamanja
Lapeza (omwe ndi akazi ogwidwa
Pankhondo) chomwe Mulungu
Wakupatsa, ndi ana achikazi a
m'bale wa Atate ako, ndi ana
achikazi a mlongo Wa atate ako,
ndi ana achikazi a Atsibweni ako,
ndi ana achikazi a m'bale Wa mayi
ako amene adasamuka pamodzi
Ndi iwe, ndi mkazi wachisilamu
Atadzipereka yekha kwa Mneneri
ngati Mneneri akufuna
kumkwatira, chilolezo Ichi ncha
iwe wekha, osati Asilamu Onse.
Ndithu, tafotokoza malamulo
Amene tawakhazikitsa kwa iwo pa
1 'Edda' ndi nthawi imene mkazi amakhala pachiyembekezero asanakwatiwe
ndi mwamuna wina pambuyo posiyana. Edda zilipo za mitundu iwiri: yosiyana
ukwati yomwe mkazi amayembekezera miyezi itatu ndi yomwalira mwamuna
yomwe mkazi amayembekezera miyezi inayi ndi masiku khumi. Koma mkazi
wapakati Edda yake imatha ndikubereka. Yang'anani ndemanga ya Qur'an
(2:228).
Surat 33. Al-Ahzab Juzu 22
902
r r ^>i rr ^\y^H\ '^^
Akazi awo, ndi chimene manja
awo Akumanja apeza; (takuchitira
zimenezi iwe Wekha Mneneri
Muhammad {SAW}) kuti
Pasakhale masautso pa iwe (ngati
ukufuna Kukwatira mkazi wina
chifukwa Chofalitsa chipembedzo)
ndipo Mulungu Ngokhululuka
kwambiri Ngwachisoni.
51. Ukhoza kumchedwetsa
(posagona M'nyumba mwake)
amene wam'funa Pakati pa iwo ndi
kumuyandikitsa kwa Iwe amene
wam'funa. Ndipo amene
Wam'funa mwa amene
udawapatuka, Palibe tchimo pa
iwe. Kuchita izi Kuchititsa kuti
maso awo atonthole (Mitima yawo
ikondwe) ndipo Asadandaule;ndi
kuyanjana nacho chimene
Wawapatsa onse. Ndipo Mulungu
Akudziwa zimene zili m'mitima
Mwanu. Ndipo Mulungu
Ngodziwa Kwambiri, Ngoleza,
(salanga Mwachangu).
52. Pambuyo (pa akazi awa
amene uli nawo) Nkosaloledwa
kwa iwe kukwatira akazi Ena,
(poonjezera pachiwerengero cha
akazi Amene uli nawo). Ndiponso
usasinthe (Ofanana ndi
chiwerengero chawo), (Zonsezi
nzoletsedwa kwa iwe) ngakhale
Kuti ubwino wawo
utakusangalatsa, Kupatula chimene
S u rat 33. Al-Ahzab Juzu 22
903
XT frjJH
TT ^Ij^-Sl *jj~>
dzanja lako lakumanja Lapeza;
Ndipo Mulungu ndimlonda
Wachinthu chilichonse.
53. E, inu amene
mwakhulupirira! Musalowe
m'nyumba za Mneneri
Pokhapokha chilolezo
Chitaperekedwa kwa inu kukadya,
osati Kukhala nkuyembekezera
kupsa kwa Chakudya. Koma
mukaitanidwa, Lowani. Ndipo
mukamaliza kudya, Balalikanani;
ndiponso musakambe Nkhani
zocheza. Chifukwa kutero
Kumavutitsa Mneneri. Ndipo iye
Amakuchitirani manyazi (kuti
Akutulutseni); koma Mulungu
alibe Manyazi ponena choona.
Ndipo inu Mukamawafunsa (akazi
ake) za ziwiya, Afunseni uku muli
kuseri kwa Chotsekereza. Kuchita
zotere, kuyeretsa Mitima yanu ndi
mitima yawo. Sikoyenera kwa inu
kumvutitsa Mtumiki wa Mulungu,
ndiponso Nkosayenera kwa inu
kukwatira akazi Ake pambuyo pa
imfa yake mpaka Muyaya. Ndithu,
kutero ndi tchimo Lalikulu kwa
Mulungu. 1
Anasi(RA) adanena kuti ndime iyi idatsika chifukwa cha anthu ena omwe
ankangocheza m'nyumba ya Mtumiki(SAW), osatulukamo. Izi zidali motere:
Pamene Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) adakwatira Zainabu
Binti Jahashi, adachita phwando la chakudya ndipo adaitana anthu. Pamene
adatha kudya ena a iwo adangokhala nkumacheza m'nyumba ya Mtumiki
(madalitso ndi mtendere zikhale naye). Pamenepo nkuti mkazi wake
atayang'anitsa nkhope yake kukhoma la nyumba. Zoterezi zidamuvuta
Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) kuti awatulutse m'nyumbamo.
Apa mpamene Mulungu adavumbulutsa ndimeyi.
Surat 33. Al-Ahzab Juzu 22
904 | tt *>i tr yjj^i 5jj^
54. Chilichonse chimene
mungachionetse Kapena kuchibisa,
(Mulungu achidziwa, Ndithu)
chifukwa chakuti Mulungu
Ngodziwa chilichonse.
55. Palibe tchimo pa iwo
(akazi) kuonana Ndi atate awo
ngakhale ana awo, alongo Awo,
ana amuna alongo awo, ana a
Amuna a abale awo, akazi anzawo,
Ndi amene manja awo akumanja
apeza. Ndipo opani Mulungu (inu
akazi). Ndithu, Mulungu ndimboni
pa chilichonse.
56. Ndithu, Mulungu
akumtsitsira madalitso Mtumiki
Wake; nawonso angero Ake
(Akumphempherera chifukwa cha
Zochita zake zabwino). E, inu
amene Mwakhulupirira!
Mpemphereni Madalitso ndi
kumpemphera mtendere (Chifukwa
chokusonyezani njira Yolungama).
57. Ndithu, amene akukwiyitsa
Mulungu Ndi kuvutitsa Mtumiki
Wake (ponyozera Malamulo ake)
Mulungu Wawatemberera padziko
lapansi(Mpaka) pa tsiku la
chimaliziro, ndipo Wawakonzera
chilango chosambula.
58. Ndipo amene akuvutitsa
Asilamu Aamuna ndi Asilamu
aakazi popanda Kuchimwa
kulikonse, ndithu, Achisenza
chinyengo ndi tchimo Loonekera.
&C*"**
Surat 33. Al-Ahzab Juzu 22
905 y t tj±\ rr ^>\^H\ t^
59. E, iwe mneneri! Uza akazi
ako, ndi ana Ako aakazi, ndi akazi
a Asilamu, kuti Adziphimbe ndi
nsalu zawo (Akamatuluka
m'nyumba), kutero Kuchititsa kuti
adziwike, asazunzidwe (Ndi anthu
achipongwe). Ndipo Mulungu
Ngokhululuka Kwambiri
Ngwachisoni.
60. Ngati sasiya (machitidwe
awo oipa) (Amunafikina)
achinyengo, ndi amene Ali ndi
matenda m'mitima mwawo
(Achiwerewere), ndi ofalitsa mbiri
Zoipa mumzinda, tikukhwirizira
kwa I wo (kuti uwathire nkhondo).
Kenako Sadzakhala m'menemo
pamodzi ndi iwe, Koma nthawi
yochepa.
61. (Iwo) ngotembereredwa;
paliponse Pamene apezeke,
agwidwe ndi Kuphedwa, ndithu.
62. (Awa ndi) machitidwe a
Mulungu omwe Adalipo pa omwe
adamka kale. Sungapeze kusintha
Pamachitidwe a Mulungu.
63. Anthu akukufunsa za (kudza
kwa) nthawi (Ya tsiku la
chitsiriziro). Nena: "Kuzindikira
kwa nthawiyo kuli ndi Mulungu
(yekha). Nanga nchiyani
Chikudziwitse kuti nthawi ya
chimaliziro Iri pafupi?
»-fr»f '.ii. k <f » «'
$jK>Sa^(
V>1
®%?£&&\&?(g$%
Surat 33. AI-Ahzab Juzu 22 906 t T *>» TT *-^SM ojj~-
64. Ndithu, Mulungu
wawatemberera Osakhulupirira ndi
kuwakonzera moto Woyaka
kwambiri;
65. Adzakhala m'menemo
muyaya. Sadzapeza bwenzi
Ngakhale mthandizi.
66. Tsiku limene nkhope zawo
Zikatembenuzidwa ku moto
(Zikutenthedwa), uku akunena:
"Kalangaife! Tikadamumvera
Mulungu Ndi kumveranso
Mtumiki(SAW), (sibwenzi Tili
m'chilangomu)"
67. Ndipo adzanena: "O, Mbuye
wathu! Ndithu, ife tidamvera
olemekezeka athu, Ndi akuluakulu
athu, choncho Adatisokeza njira.
68. Mbuye wathu! Apatseni
chilango Pamwamba pa chilango
ndipo Atemberereni, kutemberera
Kwakukulu."
69. E, inu amene
mwakhulupirira! Musakhale
monga amene adamvutitsa Musa;
koma Mulungu adamuyeretsa
Kuzimene ankamnenera. Ndipo iye
Kwa Mulungu adali wolemekezeka. 1
^^a^t^i^^a
'>\>l' Mil 1 *9>*>f 9&.1"'
%
©!£|EJ
1 M'ndime iyi, Mulungu akulangiza Asilamu kuti asamuvutitse Mtumiki ndi
kumnenera mawu opanda ulemu monga momwe Ayuda ankamunenera Musa
Ana a Israeli adamunamizira Musa kuti ali ndi khate pathupi lake, kapena kuti
ali ndi matenda a mwera (phudzi). Koma Mulungu adamuyeretsa kuzomwe
adali kumunamizirazo. Adamuyeretsa motere monga momwe Bukhari
akunenera muhadisi yomwe idalandiridwa kuchokera kwa Abu Huraira (RA)
kuti Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) adati: Musa adali munthu
Surat 33. Al-Ahzab Juzu 22 I 907 I tt *>» YT ^»\yH\ 5j>*
70. E, inu amene
mwakhulupirira! Opani Mulungu
(pokwaniritsa Malamulo Ake, ndi
kusiya zoletsedwa), Ndipo nenani
mawu olungama,
71. Akukonzerani bwino zochita
zanu ndi Kukukhululukirani
machimo anu. ndipo amene
akumvera Mulungu ndi Mtumiki
Wake, ndithu, apambana;
kupambana kwakukulu.
72. Ndithu, Ife tidapereka
malamulo athu Kuthambo ndi
nthaka ndi mapiri; koma Zidakana
kuwasenza (malamulowo); ndipo
Zidawaopa. Koma munthu
adawasenza; Ndithu, iye
ngwachinyengo kwambiri
Ndiponso mbuli.
73. Kuti Mulungu adzawalange
achinyengo Aamuna ndi aakazi, ndi
opembedza Mafano achimuna ndi
achikazi ndi kuti Adzawakhululukire
Asilamu achimuna Ndi achikazi.
Ndipo Mulungu Ngokhululuka
kwabasi, Ngwachisoni.
\py&\\&\PY£0$%
'■* 'A*4
'(s
:-,v'4i»,i»rxi«r>^
wamanyazi, ndipo amabisa thupi lake. Khungu lake silimaoneka chifukwa cha
manyazi ake. Ndipo adamuvutitsa ena mwa ana a Israeli. Adati:
"Sangadzibise motere koma khungu lake pali chochititsa manyazi, mwina
khate kapena matenda amphepo yamwera (phudzi), kapena matenda ena
aliwonse!" Ndipo Mulungu adafuna kumuyeretsa kuzimene ankamunamizirazo.
Tsiku lina Musa adakhala payekha navula nsalu zake naika pamwala. Kenako
adayamba kusamba. Pamene adamaliza kusamba adacheukira komwe
adaika nsalu zake kuti azitenge Adaona mwala ukuthawitsa nsalu zake. Musa
adatenga ndodo yake nkumathamangira mwalawo uku akunena: "Nsalu zanga,
iwe mwala! Nsalu zanga iwe mwala!" Mpaka adadutsa pomwe adakhala
akuluakulu a ana alsraeli namuona thupi lake lili losalala kwabasi; lopanda
chilema chilichonse. Potero Mulungu adamuyeretsa kuzomwe ankamunenerazo.
Surat 34. Saba' Juzu 22
908 tt *j*-» rt L-«j>-
Sura yolemekezekayi yayamba ndi kulemekeza Mulungu
Yemwe adayambitsa zolengedwa ndi kulongosola zinthu Zake
zam'dziko zakuya. lye ndi Mlengi Wanzeru zakuya Yemwe
palibe chimene chingabisike kwa lye m'kudziwa Kwake,
ngakhale kachinthu kolemera monga nyerere muthambo ndi
m'nthaka. Ndipo ichi nchisonyezo chachikulu chosonyeza
umodzi wa Mbuye wazolengedwa.
Surayi yafotokoza nkhani yaikulu kwambiri yomwe ndi
kusakhulupirira kwa opembedza mafano pa tsiku la chimaliziro
ndi kutsutsa kwawo zakuuka kuimfa. Ndipo yalamula Mtumiki
kuti alumbirire kwa Mbuye wake Wamkulu potsimikiza kuti
ndithu, kuuka kuimfa kulipo pambuyo poonongeka matupi.
Yafotokozanso nkhani za aneneri ena; yafotokoza za Daudi
ndi mwana wake Sulaiman (mtendere wa Mulungu ukhale pa
iwo) ponena kuti Mulungu adawadalitsa ndi madalitso ambiri
monga kumgonjetsera mphepo Mneneri Sulaiman kuti
imtumikire, monganso kumgonjetsera mbalame ndi mapiri
Mneneri Daudi kuti zikhale zikuthandizana naye polemekeza
Mulungu, ndi madalitso ena ambiri.
Surayi yafotokozanso maganizo a opembedza mafano ndi
okaikira uthenga wa Mtumiki Muhammad (mtendere wa
Mulungu ukhale pa iye). Ndipo yapereka mitsutso yothetsa
chikaiko chawocho. Ndipo Surayi yamaliza ndi kuitana opembedza
mafano kuti akhulupirire Mulungu mmodzi wamphamvu Yemwe
m'manja Mwake muli chikonzero cha chinthu chilichonse.
Surat 34. Saba'
Juzu 22
909
TT frjA-i
T t t-*» 0j j-*»
S«ra/Sa6a'AXX7K
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Kuyamikidwa kwaulemu
nkwa Mulungu Yemwe
zakumwamba ndi Zapansi
nzake.Ndipo kutamandidwa Konse
kwaulemu pa tsiku lomaliza
Nkwake. ndiponso lye Ngwanzeru
Zakuya, Ngodziwa chilichonse.
2. Akudziwa zimene zikulowa
m'nthaka Ndi zimene
zikutulukamo; ndi zimene
Zikutsika kumwamba ndi zimene
Zikukwera kumeneko.Ndipo lye
Ngwachifundo kwabasi,
Ngokhululuka kwambiri. 1
3. Ndipo osakhulupirira
adanena: "Siizatidzera nthawi
(Kiyama)." Nena: "lyayi!
Ndikulumbira Mbuye Wanga,
ndithu, ikudzerani. (Mbuye
Wanga) Wodziwa zobisika
(zonse), Sichingabisike kwa lye
cholemera ngati Nyerere;
chakumwamba,chapansi Ngakhale
chochepa kuposa Chimenecho;
ngakhale chokulirapo, Koma
o&g\&3\&\j
^
fa J *!. J.C*
-V •* 'W
1 M'ndime iyi Mulungu akutidziwitsa kuti akudziwa zonse zimene zikulowa
m'nthaka monga madzi, mitembo ndi zina zotero. Ndipo akudziwanso zimene
zikutuluka m'menemo - monga mmera tizirombo, miyala yamtengo wapatali
ndi madzi. Ndi zomwe zikutsika kumwamba monga mvula, matalala, mphenzi,
madalitso, angero Ake ndi mabuku Ake. Ndipo akudziwanso zimene
zikukwera kumwamba - monga ntchito za akapolo Ake ndi zina zotero.
Surat 34. Saba'
Juzu 22
910
yy frj*-i
ft U 5 j j-j
(zonsezo) zili m'Buku (Lake)
Losonyeza poyera (chilichonse).
4. Kuti adzawalipire amene
akhulupirira Ndi kuchita zabwino;
iwo adzapeza Chikhululuko ndi
zopatsidwa zaulemu."
5. Koma amene alimbika
kutsutsana ndi Aya zathu
pomaganiza kuti Atigonjetsa, pa
iwo pali chilango Chopweteka.
6. Koma amene apatsidwa
(dalitso la) Kudziwa akuzindikira
kuti zimene Zavumbulutsidwa kwa
i we kuchokera Kwa Mbuye wako
nzoona, Ndipo zikuongolera ku
njira ya Mwini Mphamvu zoposa;
Wotamandidwa.
7. Ndipo osakhulupirira
akunena (pouzana Pakati pawo
mwachipongwe): "Kodi
Tikusonyezeni zamunthu yemwe
Akukuuzani kuti (m'kadzafa) ndi
Kudukaduka m'dzakhala
m'chilengedwe Chatsopano?"
8. (Mulungu akunena): "Kodi
(Akum'ganizira Muhammad kuti)
Wapekera Mulungu bodza, kapena
Wagwidwa ndi misala? Iyayi,
koma Osakhulupirira za tsiku la
chimaliziro Adzakhala m' chilango
ndi m'kusokera Kwakukulu.
9. Kodi (agwidwa ndi khungu)
saona Zomwe zili patsogolo pawo
ndi Pambuyo pawo monga thambo
**••
Surat 34. Saba'
Juzu 22
911
rr *>i
V* t l--»» * j j-*i
ndi Nthaka (kuti adziwe kukhoza
Kwathu Kuchita zimene tafuna)?
Tikadafuna Tikadawakwirira ndi
nthaka kapena Kuwagwetsera
zidutswa za thambo. Ndithu,
m'zimenezo muli malingaliro Kwa
kapolo aliyense wotembenukira
(Kwa Mulungu).
10. Ndithudi, Daudi tidampatsa
chisomo Chachikulu chochokera
kwa Ife. (Ndipo Tidauza mapiri
kuti akhale akuvomereza
Mapemphero a Daudi
pothandizana Naye. Tidati): "E,inu
mapiri pamodzi Ndi iye Daudi,
lemekezani (Mulungu), Ndi inunso
mbalame." Ndipo
Tidamufewetsera chitsulo.
11. (Tidati kwa iye:) "Panga
zovala (Zachitsulo) zophanuka
(zokwana thupi Lonse,
zodzitetezera pa nkhondo), Ndipo
linga bwino m'kulumikiza ndi
Poluka. Potero chitani zabwino,
(ee, inu Akubanja la Daudi!).
Ndithu, Ine Ndikuona zonse
zimene mukuchita." 1
12. Nayenso Sulaiman
tidamgonjetsera Mphepo (yomwe
inkayenda mwa Lamulo lake).
V**'"' * •
1 Mulungu Wapamwambamwamba adamfewetsera Daudi chitsulo kotero kuti
adachisungunula nkusanduka ngati phala, napanga kuchokera m'phala
limenelo zovala zodzitetezera pankhondo, ndiponso ziwiya zina zothandiza pa
umoyo. Ichi chidali chisomo chachikulu chimene Mulungu adamdalitsa nacho
iye pamodzi ndi ife tonse.
Surat 34. Saba'
Juzu 22
912
tt *>i
T i t—» o jj-»>
Mayendedwe amphepoyo
Inkayenda kuyambira m'mawa
mpaka Masana mtunda wofanana
ndi waulendo Wa mwezi umodzi;
Ndiponso Kuyambira masana
mpaka madzulo Inkayenda mtunda
wofanana ndi Waulendo wamwezi
umodzi. Ndipo Tidamsungunulira
kasupe wamtovu. Ndiponso
m'ziwanda (majini) Zidaliponso
zimene tidam'gonjetsera Zomwe
zinkam'gwirira ntchito
Mwachilolezo cha Mbuye wake
(Mulungu). Ndipo yense mwa iwo
Wonyoza lamulo Lathu (Posiya
kumumvera Sulaiman) Timulawitsa
chilango cha moto woyaka.
13. Ziwandazi zimampangira
zimene Wafuna, monga: misikiti,
zithunzi Zokhala ndi matupi, ndi
mabeseni onga Madamu ndi
midanga Yokhazikika.
(Tidawauza:) "Chitani Ntchito
zabwino, E, inu akubanja la Daudi
pothokoza (madalitso amene
Mwapatsidwa). Komatu ndiochepa
Othokoza mwa akapolo Anga"
14. Pamene tidalamula imfa
yake (Sulaiman), palibe chimene
Chidawasonyeza za imfa yake
koma Kachirombo kam'nthaka
(chiswe) Kamene kadadya ndodo
yake. Choncho Pamene adagwa,
ziwanda zidazindikira Kuti
zikadakhala zikudziwa zobisika
Surat 34. Saba'
Juzu 22
913 "*>»
Tt L»» 5 j y>
Sizidakakhala m'chilango
Chosambulacho. 1
15. Ndithu, padali phunziro pa
anthu A dziko la Saba mokhala
mwawo: (Padali) minda iwiri,
Kumanja ndi kumanzere. (Tidati:)
"Idyani riziki (zaulere) Lochokera
kwa Mbuye warm, ndipo
Mthokozeni. Mudzi wabwino ndi
Mbuye Wokhululuka.
16. Koma adanyozera (lamulo
la Mulungu); choncho
tidawatumizira Chigumula
champhamvu (chomwe
Chidawamiza ndi kuononga minda
Yawo). Ndipo tidawasinthira
Minda yawo (yabwino) kukhala
minda Iwiri yazipatso zowawa, ndi
mitengo Ya isili (yomwe
chikhalirenicho ndi Yosabereka
zipatso,) ndi mitengo Pang'ono ya
masawu. 2
*»i<
®jj*>
1 Kalelo anthu adali ndi chikhulupiriro chakuti ziwanda zimadziwa zamseri;
monga kudziwa zam'tsogolo. Ndipo kudapezeka kuti Sulaiman adaimirira
kupemphera ku chipinda chake chopempherera uku atatsamira ndodo yake,
imfa niimpeza ali chiimirire, choncho adakhala chaka chathunthu ali
chomwecho uku atafa kale. Mmenemo nkuti ziwanda zikugwira ntchito
yotopetsa, osadziwa kuti Sulaiman adafa, mpaka pamene chiswe chidadya
ndodo imene adatsamira, nagwa pansi. Apo mpomwe imfa yake idadziwika.
Potero anthu adadziwa tsopano kuti ziwanda sizidziwa zam'tsogolo.
2 Anthu am'mudzi wa Saba'a komwe nkudziko la Yemeni, Mulungu
adawapatsa madalitso ambiri pamene iwo amatsatira malamulo Ake ndi
kumthokoza. Adawadalitsa ndi minda ya zipatso zokoma zomwe zidalibe
nyengo yeniyeni yobalira, kotero kuti azimayi ankangosenza madengu
nkumangoyenda pansi pa mitengo ndipo mwadzidzidzi ankangoona madengu
ali odzaza ndi zipatso zoyoyoka m'mitengoyo. Koma pamene adasiya
kuyamika Mulungu ndi kutsatira malamulo Ake, adawaonongera mindayo ndi
chigumula ndi kuwasinthitsira zipatso zawo ndi zipatso zopanda pake.
Surat 34. Saba'
Juzu 22
914
tt *>i
Ti t-*» 5jj-*»
17. Amenewo ndiwo malipiro
omwe Tidawalipira chifukwa cha
Kusathokoza kwawo (Mtendere
wa Mulungu). Ndipo Ife sitilipira
zoterezi koma Kwa okhawo
osathokoza.
18. Ndipo pakati pawo ndi
pakati pamidzi Imene tidaidalitsa,
tidaikapo midzi Imene idali
yoonekera; ndipo tidapima
M'menemo malo
apaulendo.(Kotero Kuti amachoka
malo nkufika malo Ena
mosavutika. Tidawauza):
"Yendani M'menemo usiku ndi
usana Mwamtendere."
19. Koma (adauda mtendere
umenewu;) Adati: "O, Mbuye
wathu! Talikitsani mtunda pakati
pa maulendo Athu; (kuyandikirana
kwa midzi, Sikukutisonyeza kuti
tili paulendo);" Choncho
adadzichitira okha zoipa. Ndipo
tidawachita kukhala Miyambi
(imene anthu a pambuyo
Ankauzana pakati pawo), ndipo
Tidawabalalitsa; kubalalikana zedi.
(Ena adathawira dziko ili, ena dziko
lina). Ndithu, m'zimenezo muli
Malingaliro kwa yense wopirira
Kwabasi ndi wothokoza kwambiri.
20. Ndipo ndithu, Iblis
adatsimikiza Ganizo lake pa iwo
choncho Adamtsatira kupatula
Gulu la okhulupirira (moona).
99?"$?'; <{ji/ 9>\?\ 9 *\' <.<&'' *'\"
Surat 34. Saba'
Juzu 22
915 l*Y»>i
V t L-*» 3 j j-»»
••
21. Ndipo iye adalibe nyonga
pa iwo, koma Chifukwa chakuti
tionetse poyera ndani
Wokhulupirira tsiku lachimaliziro
Ndiponso ndani amene
akulikaikira. Ndipo Mbuye wako
Ngosunga chilichonse. 1
22. Nena: "Itanani amene
mukuwatcha kuti Ndi milungu
kusiya Mulungu (kuti
Akuthandizeni. Koma
Sangakuthandizeni chilichonse;
Pakuti iwo) alibe ngakhale
kachinthu Kakumwamba ndi pansi
kolemera ngati Nyerere yaing'ono
kwambiri; M'menemo iwo alibe
gawo lililonse (Lothandizana ndi
Mulungu), Ndipo ngakhale Iyenso
alibe mthandizi Wochokera mwa
iwo.
23. Ndipo uwomboli
sudzathandiza kwa Iye (Mulungu)
kupatula amene Wamuloleza."
Choncho (zikatero) kuti,Pamene
mantha adzachotsedwa M'mitima
mwawo (popatsidwa Chilolezo
choti apulumutse ena), Adzanena
pakati pawo (mosangalala): "Kodi
wanena chiyani Mbuye wanu?"
(Adzayankha), "Ndithu, Iye wanena
choona; Iye Ngotukuka Ngwamkulu.
Pamene satana adatha kumsokeretsa Adamu adaganizanso kuti adzatha
kuwasokeretsa ana ake. Ndipo ana a Adamu adamtsatiradi satanayo monga
momwe iye ankaganizira. Komatu satana alibe mphamvu zomkakamizira mwana
wa Adamu kuti amtsate koma amangomuitana kupyolera m'kukometsera
ziiakolako zoipa.
Surat 34. Saba'
Juzu 22
916
TT tj)r\
T t L— » 5 j j-»
24. Nena (kwa iwo, iwe
Mneneri{SAW}): "Kodi Ndani
amakupatsani riziki (zaulere)
Kuchokera kumwamba ndi pansi?"
(Ngati sakuyankha chifukwa
Chodzitukumula), nena (kwa iwo):
"Ndi Mulungu (mmodzi, amene
Akukupatsani zopatsa zaulere
Zochokera kumwamba ndi
pansi);Ndipo ife kapena inu, tili
pachiongoko Kapena mkusokera
koonekera"
25. Nena: "Simudzafunsidwa
pazolakwa Zimene (ife) talakwa,
nafenso Sitidzafunsidwa pazimene
mukuchita."
26. Nena (kwa iwo): "Mbuye
wathu Adzatisonkhanitsa pakati
pathu (Pa tsiku la chiweruzo).
Kenako Adzaweruza pakati pathu
Mwachoonadi; lye ndi Muweruzi
Wodziwa kwambiri."
27. Nena (kwa iwo):
"Ndisonyezeni amene
Mwawalumikiza ndi lye monga
Othandizana naye; Iyayi,
sizingatheke (lye kukhala ndi
anzake) koma lye (Yekha) ndiye
Mulungu, Mwini Mphamvu
zoposa, Wanzeru zakuya."
28. Ndipo sitidakutumize (iwe,
Mtumiki{SAW} Kwa Arabu okha)
koma kwa anthu onse, kuti ukhale
wouza okhulupirira Nkhani
.? 4 \\i
iJP$$^\&v$£5$&
*&^0®ZS&$
©Z&\pB&
Siirat 34. Saba'
Juzu 22
917
TY fjA-i
rt l*» s jj~>
zabwino ndi wochenjeza Otsutsa.
Koma anthu ambiri sadziwa (Za
uthenga wako).
29. Eti akunena: "Nliti
lidzakwaniritsidwe Lonjezo ili
(lakudza kwa chiweruziro) Ngati
mukunenadi zoona?
30. Nena: "Muli nalo pangano
(Lotsimikizika) la tsiku (limenelo)
Limene simungathe kulichedwetsa
Ngakhale ola limodzi,kapena
Kulifulumizitsa."
31. Ndipo amene sadakhulupirire
akunena: "Sitiikhulupirira Qur'an
iyi, Ngakhalenso mabuku aja
apatsogolo Pake. "Ndipo
ukadawaona achinyengo Pamene
azikaimiritsidwa pamaso pa
Mbuye wawo, (ukadaona zoopsa
Zazikulu), uku pakati pawo
Akubwezerana mawu. Amene
Adaponderezedwa adzanena kwa
amene Adadzikweza:
"Kukadapanda Inu (Kutipondereza),
tikadakhala Asilamu."
32. Amene adadzikweza
adzanena kwa amene
Adaponderezedwa: "Ha, kodi ife
Tidakutsekerezani kuchiongoko
Chitakudzerani? Iyayi, koma
mudali Oipa."
33. Ndipo amene
adaponderezedwa Adzanena kwa
amene adadzikweza: "Iyayi, koma
1 <&Jr**jM{)i
Surat 34. Saba'
Juzu 22
918
YY frji-1
ft L») 5 jj-o
(mumachita) ndale za usiku Ndi
usana (zotitsekereza nazo
Kuchikhulupiriro) pamene
Mumatilamula kuti tinkanire
Mulungu Ndikumpangira lye
milungu inzake". Iwo adzabisa
madandaulo pamene Adzaona
chilango. Ndipo tidzaika Magoli
m'makosi mwa amene
Sadakhulupirire; kodi angalipidwe
China, osati zija ankachita. 1
34. Palibe pamene tidatuma
mchenjezi M'mudzi uliwonse
koma opeza bwino Am'mudzimo
ankanena: "Ndithu, ife Tikuzikana
zimene mwatumidwa Nazozi."
35. Ndipo ankanena (monyada):
"Ife tili Ndi chuma chambiri ndi ana
(ambiri); Choncho ife sitidzalangidwa
(pa tsiku la chimaliziro)."
36. Nena: "Ndithu, Mbuye
wanga Amamchulukitsira riziki
(zopatsa) Laulere amene wamfuna
(ngakhale ali Woipa), ndipo
amamchepetsera (amene Wamfuna
ngakhale kuti ndi munthu
Wabwino). Koma anthu Ambiri
sazindikira (zimenezi)."
M'ndime iyi, Mulungu akutifotokozera kuti patsiku la chimaliziro padzakhala
kukangana pakati pa atsogeleri ndi anthu otsogoleredwa. Izi zidzachitika
pamene otsogoleredwa adzatsimikiza kuti atsogoleri awo amawasokeza;
ankangowalangiza zachabe. Potero adzakhala ndi madandaulo aakulu chifukwa
chotsatira anthu osokera. Komatu madandaulo oterewa sadzawapindulira
chilichonse popeza mwayi udzakhala utatha kale. Choncho nkofunika kuti
potsata mtsogoleri aliyense tiyambe taganizira komwe akunka nafe;
tisangokokedwa ngati nyama pakuti Chauta adatipatsa dalitso lanzeru.
Choncho tigwiritse ntchito bwino nzeru tsoka lisanatigwere.
Surat 34. Saba 9
Juzu 22
919 I tY,>i
V £ L-*» 3 j j-»
37. Ndipo sichuma chanu ndi ana
anu zomwe Zingakuyandikitseni
kwa Ife, koma (Chikhulupiriro
cha) amene Wakhulupirira ndi
kuchita zabwino. Iwo adzapeza
malipiro owonjezeka Kwambiri
pazomwe adachita. Iwo adzakhala
mwamtendere M'zipinda za ku
Minda ya Mtendere.
38. Ndipo amene akuchita
khama Kulimbana ndi zizindikiro
Zathu ndi Cholinga choti
alepheretse (zofuna Zathu,)
iwowo adzabweretsedwa
Kuchilango (chamoto).
39. Nena (iwe Mneneri):
"Ndithu, Mbuye Wanga
amamchulukitsira riziki (zaulere)
Amene wamfuna mwa akapolo
Ake; Ndiponso amamchepetsera
(Amene wamfuna). Ndipo
Chilichonse chimene mupereka,
lye Adzakupatsani china m'malo
mwake; lye Ngwabwino popatsa
zaulere, Kuposa opatsa.
40. Ndipo (kumbuka iwe
Mneneri) tsiku limene (Mulungu)
adzawasonkhanitsa onse ndi
Kunena kwa angero: "Kodi awa
Amapembedza inu?"
41. Adzanena: "Kuyera konse
nkwanu (Simungakhale limodzi
ndi milungu ina!) Inu ndinu
Mtetezi wathu, Osati iwo. Koma
••
%&&X&<£\&£>\&
2F
&?&&&&&
Surat 34. Saba'
Juzu 22
920
YY *>l
T t L-*» 5 j j-*>
amagwadira majini(Ziwanda);
ambiri mwa iwo (anthu)
Adakhulupirira izo (ziwanda)".
42. (Mulungu adzawauza iwo:)
"Lero Aliyense mwa inu sangathe
kudzetsa Zabwino ngakhale
masautso pa ena." Ndipo
tidzawauza amene adadzichitira
Okha zoipa: "Lawani chilango
chamoto Chimene munkachitsutsa".
43. Ndipo aya zathu zofotokoza
momveka Zikamawerengedwa
kwa iwo, amanena, "Sichina uyu
(Muhammad {SAW}) Koma ndi
munthu yemwe akufuna
Kukutsekerezani mapemphero
amene Amapemphera makolo
anu."Ndipo Akunena: "Sichina iyi
(Qur'an) Koma ndibodza
lopekedwa". Ndipo Amene
sadakhulupirire akunena Pachoona
pamene chawadzera: "Sikanthu ichi,
koma ndi matsenga Woonekera."
44. Ndipo (ngakhale awa
Arabu) Sitidawapatse mabuku oti
aziwawerenga (Buku ili lisanadze);
ndipo Sitidawatumizirenso
mchenjezi Patsogolo pako. (Nanga
akudziwa Bwanji kuti Qur'an iyi
ndiyonama?)
45. Ndipo amene adalipo
iwowo kulibe, Adatsutsa,ndipo
(awa Arabu) sadapeze Chigawo
chimodzi m'zigawo khumi
Zazomwe tidawapatsa iwowo, Koma
©/
L5
Surat 34. Saba'
Juzu 22
921 "*>'
V t L— » 5j j-j
adatsutsa atumiki Anga (Pa zomwe
adawabweretsera). Nanga chidali
bwanji Chilango Changa (pa iwo).
46. Nena: "Ndithu
ndikukulangizani chinthu
Chimodzi, kuti muimirire
chifukwa cha Mulungu; awiriawiri
ndi Mmodzimmodzi, ndipo kenako
Mulingalire; (muona kuti uyu
Muhammad {SAW} chilichonse
chomwe Akunena nchoona.
Ndiponso muona Kuti) mnzanuyu
alibe misala. lye, Sichina, koma
ndimchenjezi wanu Chisanadze
chilango chaukali."
47. Nena: "Chilichonse
ndakupemphani kukhala Malipiro
(othandizira kufikitsa uthenga Kwa
anthu) ndichanu, malipiro anga ali
kwa Mulungu basi. Ndipo lye Ndi
Mboni pachilichonse."
48. Nena: "Ndithu, Mbuye wanga
Amaponya choonadi (ponseponse
Kotero kuti chonama chimathawa).
Ngodziwa (zinthu) zobisika."
49. Nena: "Choonadi chadza
(chisilamu); Ndipo chabodza
(chipembedzo cha mafano)
Sichidzetsa zachilendo. Ndiponso
Sichibwerera (kukhala ndi nyonga
monga Kale)."
50. Nena: "Ngati ndasokera,
ndiye kuti Ndadzisokeretsa ndekha
(ndadziyika Ndekha m'mavuto).
®&£
Surat 34. Saba'
Juzu 22
922
YY *j*-»
T i L-» 5 j j-»
Koma ngati Ndaongoka,
ndichifukwa cha zimene
Akundivumbulutsira Mbuye
wanga. Ndithu, lye Ngwakumva;
ali Pafupi (ndi aliyense)."
51. Ndipo ukadaona pamene
Adzanjenjemera (akadzachiona
Chilango cha Mulungu, adzayesera
Kuthawa), koma sipadzapezeka
Pothawira, ndipo adzagwidwa
Pamtunda wapafupi (asanafike
kutali).
52. Ndipo adzanena
(mophuphaphupha) :
"Tachikhulupirira (tsopano
Chipembedzo cha Chisilamu)."
Koma iwo angaulandire chotani
Usilamu kumeneko (komwe)
ndikumalo Akutali,
53. Pomwe chikhalirenicho
adachikana Kale Chisilamu. Ndipo
chobisika Ankachigenda (ndi
bodza) Kuchokera kumalo akutali,
54. Ndipo padzatsekeka pakati
pawo ndi Zimene akuzilakalaka,
monga momwe Adachitidwira
anzawo akale. Ndithu, Iwo adali
m'chikaiko chowakaikitsa
(Uthenga wa Mulungu).
®&jf4&*'&\
Siirat 35. Fatir Juzu 22
923
YY *j*-t To J?\& l^y*
SURAT FATIR XXXV
^J£:
Surayi idavumbulutsidwa ku Makka, Mtumiki Muhammad
(madalitso ndi mtendere zikhale naye) asadasamuke. Cholinga
chachikulu cha Surayi ndikulimbikitsa chikhulupiriro mu umodzi
wa Mulungu ndi kukhoza Kwake ndi kupereka zisonyezo kuti
lye alipo. Ndi kuthetseratu maziko a kuphatikiza Chauta ndi
zinthu zina, ndi kulimbikitsa kuti mitima iyeretsedwe ku zoipa,
ndi kuikometsa ndi makhalidwe abwino.
Surayi yafotokoza poyamba za Mlengi, amene adalenga
zolengedwa zonse popanda chofanizira. Adalenga angelo, anthu
ndi ziwanda.
Ndipo yapereka zisonyezo ndi maumboni zomwe zisonyeza
kuti kuuka kwa akufa kudzachitikadi. lye amaukitsa nthaka
youma pogwetsa mvula kuti imeretse mmera womwe
umatulutsa zipatso ndi mbewu zosiyana mitundu. lye ndi Amene
adapanga usiku ndi usana kuti uzisinthanasinthana; kusinthana
komwe kukusonyeza mphamvu Zake. Ndiponso m'kalengedwe
ka munthu muli zisonyezo zosonyeza mphamvu Zake pomwe
adamlenga m'njira zosiyansiyana.
Surayi yafotokozanso za kusiyana kwakukulu komwe kulipo
pakati pa okhulupirira ndi osakhulupirira. Ndipo yafanizira
munthu wosakhulupirira ngati munthu wosapenya; wokhulupirira
ngati munthu wopenya.
Yafotokozanso za kukhoza kwa Mulungu pakusiyanitsa
mitundu ya zipatso ndi zolengedwa zina, monga anthu, nyama
ndi miyala. Zonsezi zikusonyeza ukulu Wake ndi kukhoza Kwake.
Surayi yafotokozanso kuti otsatira Muhammad (madalitso ndi
mtendere zikhale naye) apatsidwa uthenga wolemekezeka woposa
mauthenga ena onse ochokera kumwamba, powavumbulutsira Buku
lolemekezeka lomwe mkati mwake muli zonse zimene zimapezeka
m'Mabuku akale. Ndi kuti omtsatira agawidwa m'magulu atatu:
(a) Onyozela malamulo (b) abwino (c) achangu pochita zabwino.
Ndipo Surayi yamaliza ndi kudzudzula opembedza mafano a
mitengo, miyala ndi zithunzi za anthu.
Surat 35. Fatir
Juzu 22
924
YY *jA-l
fO ^13 9jy>
Surat Fatir XXXV
'm-t mm-.
jit.
0&£\(£&\&\j
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Kuyamikidwa konse nkwa
Mulungu (Yekha) Muumbi wa
thambo ndi nthaka (Popanda
chofanizira), amene adachita
Angelo kukhala atumwi eni
mapiko, Awiriawiri; atatuatatu; ndi
anayianayi. Amaonjezera
mkulenga monga momwe Afunira,
(palibe chimene chihgakanike Kwa
lye). Ndithu, Mulungu Ngokhoza
Chilichonse. 1
2. Chifundo chimene Mulungu
angatsekule Kwa anthu, palibe
amene Angachitsekereze. Ndipo
chimene Angachiletse palibe
amene Angachipereke kupatula
lye. Ndipo lye Ndi mwini
Mphamvu zoposa,Wanzeru Zakuya.
1 (Ndime 1-2) lye Mulungu ali ndi mphamvu pa chilichonse; chimene afuna
kuti chichitike chimachitika Ndipo palibe chimene chingakanike kulengeka ndi
lye ngati atafuna kuti chilengeke. Mulungu wadzitamanda m'ndime ziwirizi ndi
makhalidwe Ake awiri apamwamba. Khalidwe loyamba, ndikukhoza komwe
ndikusalephera chilichonse chimene wafuna. Khalidwe Lake lachiwiri ndikudalitsa
madalitso osiyanasiyana pa zolengedwa Zake. Mulungu adalenga thambo ndi
nthaka popanda chofanizira, natukula thambo kumwamba popanda mzati
nalikongoletsa ndi nyenyezi. lye ndi Yemwe adayalanso nthaka naika
mmenemo mmera monga chakudya cha zamoyo, nang'ambamo nyanja ndi
mitsinje ndi akasupe ndi zina zotero zomwe zikusonyeza mphamvu Zake
zoposa ndi luso Lake. Ndime yachiwiriyi ikutiphunzitsa kuti chimene Mulungu
wachipereka kwa munthu monga chuma kukhala ndi moyo wangwiro, kukhala
ndi nzeru zakuthwa, palibe amene angazitsekereze zimenezi. Ndipo chimene
Mulungu wam'mana munthu, palibe amene angathe kuchipereka kwa iye.
©;«&
Surat 35. Fatir
Juzu 22
925 I H^i
To ^\3 5jj-»>
3. E, inu anthu! Kumbukirani
mtendere Wa Mulungu omwe uli
pa inu (Pomthokoza). Kodi alipo
Mlengi wina Osati Mulungu
amene angakupatseni Riziki
kuchokera Kumwamba ndi pansi?
Palibe wina Wopembedzedwa
mwachoonadi, koma lye. Nanga
mukutembenuzidwira kuti?
4. Ndipo ngati angakutsutse
ndithu, Adatsutsidwanso atumiki
amene adalipo Patsogolo pako.
Ndipo zinthu zonse
Zidzabwezedwa kwa Mulungu.
5. E, inu anthu! Ndithu, lonjezo
la Mulungu ndi loona. Choncho
Usakunyengeni moyo wadziko
lapansi, Ngakhale mdyerekezi uja
wamkulu (Iblis), asakunyengeni pa
za Mulungu. 1
6. Ndithu, Satana ndi mdani
wanu; choncho Mchiteni kukhala
mdani. lye Amaliitanira gulu lake
kuti likhale gulu La anthu
akumoto. 2
7. Amene sadakhulupirire
(Mulungu ndi Mtumiki Wake), pa
iwo padzakhala Chilango chaukali;
koma amene Akhulupirira ndi
1 M'ndime iyi Mulungu akutichenjeza kuti tisanyengedwe ndi malangizo a
Satana akuti: "Chitani mmene mungafunire, Mulungu Wachifundo chambiri
adzakukhululukirani."
2 Mulungu watifotokozera kuti satana ndi mdani wathu wakalekale; iye ndi
amene adatulutsitsa tate wathu Adamu m'Munda wa Mtendere pomulakwitsa.
Ndipo iye adalumbira kuti adzapitiriza kutisokeretsa.
Surat 35. Fatir
Juzu 22
926
11 *>i
To ^13 5jj-*»
kumachita zabwino, Iwo adzapeza
chikhululuko ndi malipiro Aakulu.
8. Kodi amene zochita zake
zoipa Zakometsedwa kwa iye
nkumaziona Kuti nzabwino,
(ngolingana ndi amene Waongoka
ndi chiongoko cha Mulungu
Kotero kuti chabwino nkuchiyesa
Chabwino; choipa nkuchiyesa
choipa?) Ndithu, Mulungu
akumlekerera kuti Asokere yemwe
wamfuna (Chifukwa chakuti
safuna kuongoka), Ndipo
akuongola amene wam'funa.
Choncho moyo wako usaonongeke
Chifukwa chowadandaulira iwo.
Ndithu, Mulungu Ngodziwa Zonse
zimene (iwo) akuchita.
9. Ndipo Mulungu ndiamene
amatumiza Mphepo; choncho
imagwedeza Mitambo (yamvula)
ndipo timaifikitsa Kudziko
lachilala. Ndipo kupyolera
M'madzi otuluka m'mitamboyo;
Timaiwukitsa nthaka pambuyo
pakufa Kwake, (monga momwe
tikutulutsira Mbewu m' nthaka)
momwemonso Ndimmene
kudzakhalira kutuluka Akufa
(m'manda tsiku la chiweruzo.
10. Amene akufuna ulemerero,
(Amvere Mulungu), chifukwa
Ulemerero wonse ngwa Mulungu.
Kwa Iye amakwera mawu abwino.
Ndipo zochita zabwino ndi zimene
Surat 35. Fatir
Juzu 22
927
rr >>i
To ^>li 5jj-*»
Zimakweza mawu abwinowo.
Ndipo Amene akuchita ndale
zoipa, adzapeza Chilango chaukali;
ndipo ndale zawo Nzotayika,
(zoonongeka).
11. Ndipo Mulungu
adakulengani ndi dothi; Kenako
ndi dontho la umuna; kenako
Adakupangani amuna ndi akazi.
Ndipo Mkazi aliyense satenga
mimba Ndiponso sabala koma
kupyolera M'kudziwa Kwake
(Mulungu). Ndipo Amene
wapatsidwa moyo, sapatsidwa
Moyo wautali ndiponso
sachepetsedwa Moyo wake, koma
zonsezo zili m'buku (La
Mulungu) .Ndithu, zimenezo Kwa
Mulungu nzosavuta.
12. Ndipo nyanja ziwiri
(yamadzi ozizira ndi Yamadzi
amchere) sizili zofanana, Iyi
yamadzi okoma, ozuna, ndi
omweka Bwino kamwedwe kake;
ndi iyi (Ya madzi) amchere
owawa. Ndipo Kuchokera
m'zonsezi, mumadya nyama
Yamatumbi (nsomba zaziwisi).
Ndipo Mumatulutsa
zodzikongoletsera (Zimene)
mumazivala; ndipo m'menemo
Ukuona zombo zikung'amba
madzi kuti Mupeze ubwino Wake
ndi kutinso Inu muthokoze.
Surat 35. Fatir
Juzu 22
928
rr tjir\
To Jp\& 5jj-*»
13. Amalowetsa usiku mu
usana, ndi Kulowetsa usana mu
usiku; dzuwa ndi Mwezi adazichita
kuti zigonjere (Malamulo Ake).
Zonse zikuyenda (Usana ndi usiku)
kufikira nthawi Yake yodziwika.
Ameneyo ndi Mulungu, Mbuye
wanu, Mwini Ufumu. Ndipo
Amene mukuwapembedza, osati
lye, Alibe ngakhale khoko la
chipatso cha Kanjedza.
14. Ngati mutawapempha
(mafanowo), Sangamve kuitana
kwanu, ndipo ngati Atamva
sangakuyankheni (chifukwa Alibe
kukhoza kulikonse). Ndipo pa
Tsiku lomalizira, adzakana
kuphatikiza Kwanu. Ndipo palibe
(aliyense) Angakuuze monga
momwe akukuuzira (Mulungu)
Wodziwa kwambiri.
15. E, inu anthu! Inu
ndiosaukira (chinthu Chilichonse)
kwa Mulungu; koma Mulungu
Ngwachikwanekwane (sasaukira
Chilichonse kwa inu);
Wotamandidwa (Ndi zolengedwa
zonse).
16. Ngati atafuna angakuchotseni
ndi Kubweretsa Zolengedwa
zatsopano.
17. Ndipo zimenezo sizili
zovuta kwa Mulungu.
^j^=a4^^I^|<i>l
©j&y^J*^^
Siirat 35. Fatir
Juzu 22
929
Yt *>i
Y*o ^kis 3j^-»
18. Ndipo wosenza, sadzasenza
mtolo wa Wina. (Aliyense
adzasenza mtolo wa Machimo
ake). Ngakhale amene Walemedwa
ndi mtolo wake ataitana (Wina)
chifukwa cha mtolo wake Kuti
amsenzere silidzatengedwa
Ngakhale gawo pang'ono la
mtolowo (Ndi munthu ameneyo),
ngakhale Atakhala m'bale wake.
Ndithu, Ukuchenjeza okhawo
amene akuopa Mbuye wawo
pomwe sakumuona, Ndipo
akupemphera Swala, ndipo
Yemwe akudziyeretsa, ndithu,
Akudziyeretsa yekha, (ubwino
wake Umubwerera iye mwini);
ndipo Mabwerero (a zolengedwa
Zonse) ndi kwa Mulungu (basi).
19. Ndipo wakhungu ndi
wopenya Ngosafanana, (woyenda
panjira Ya choona ndi Wosokera
ngosafanana);
20. Ngakhale mdima ndi
kuunika (Nzosafanana);
21. Ngakhale mthunzi ndi
kutentha (Nzosafanana);
22. Ndipo amoyo ndi akufa
safanana (Amene mitima yawo ili
ndi moyo Pokhala ndi
chikhulupiriro, ndi Amene mitima
yawo ili yakufa Posakhala ndi
chikhulupiriro, Ngosafanana).
Ndithu, Mulungu Akumumveretsa
®&\j{jty\(Sj~^
(&2W;«S,Aih5K
%&\%bw&
Surat35. Fatir
Juzu 22
930
yy >>i
To ^kl3 ojj^t
amene wam'funa; Koma iwe
sungathe kumumveretsa Amene ali
m'manda.
23. Iwe sindiwe chinthu china,
koma Ndiwe mchenjezi.
24. Ndithu, Ife takutuma
mwachoona Kuti unene nkhani
yabwino (yokalowa Kumunda wa
Mtendere kwa amene
Akhulupirira), ndi kuti uchenjeze
(Za chilango chamoto kwa amene
Sadakhulupirire). Ndipo palibe
m'badwo Uliwonse koma
mchenjezi adapitamo.
25. Ndipo ngati angakutsutse,
(sichachilendo). Ndithu, amene
adali patsogolo pawo Adatsutsanso
Aneneri awo adawadzera Ndi
zizindikiro zoonekera poyera, ndi
Kalata ndi mabuku ounikira (Njira
yabwino).
26. Kenako ndidawathira dzanja
(Ndidawaononga) amene
adatsutsa. Nanga chidali bwanji
Chilango Changa (pa iwo).
27. Kodi sudaone kuti Mulungu
amatsitsa Madzi kuchokera
kumitambo? Kupyolera
m' madzi wo tatulutsa zipatso
Zautoto wosiyanasiyana (zakuda
Zofiira, zachikasu, zobiriwira
pomwe Madzi ake ndiamodzi
omwewo). Ndipo M'mapiri muli
timizere: toyera, Ndi tofiira,
w*££$ £%&* m>38<lij
Surat 35. Fatir
Juzu 22
931
rt c>»
f© jt\3 Sjj--
tosiyana utoto wake, Ndi (tina)
takuda kwambiri.
28. Ndipo mwa anthu ndi
nyama zokwawa, Ndi ziweto,
nchimodzimodzinso; Nzosiyana
maonekedwe ake (utoto Wake).
Ndithu odziwa ndi amene
Amamuopa Mulungu mwa
akapolo Ake. Ndithu, Mulungu
Ngwamphamvu Zoposa;
Ngokhululuka kwambiri.
29. Ndithu, amene akuwerenga
Buku la Mulungu uku
nkumapemphera napereka
Mzimene tawapatsa mwanseri ndi
Moonetsera, iwo akuyembekezera
Malonda osaonongeka,
30. Kuti akawadzadzire
malipiro awo ndi Kuwaonjezera
zabwino Zake; ndithu, lye
Ngokhululuka kwabasi;
Ngothokoza Kwambiri.
31. Ndipo Buku limene
takuvumbulutsira, Nloona;
likutsimikizira za mabuku Omwe
adali patsogolo pake. Ndithu,
Mulungu kwa akapolo Ake
Ngodziwa Kwambiri ndiponso
Akuwaona bwino.
32. Kenako tidawapatsa Buku
(Qur'an) Amene tidawasankha
mwa akapolo Athu, koma alipo
ena mwa iwo Odzichitira okha
9 W 9* " 9 ^SS iJ> *9)\ 9>'**jx
<a
9>\ 'Z
^\&K&£lj&
Surat 35. Fatir
Juzu 22 932 Y Y *>t
To ^1?13 Ojj-o
chinyengo (Pochulukitsa
machimo), ena mwa iwo
Nzofanana; ndipo ena mwa iwo
Ngopikisana pochita zabwino mwa
Chifuniro cha Mulungu. Kuteroko
Ndiwo ubwino waukulu.
33. Adzailowa Minda
yamuyaya; M'menemo
adzakongoletsedwa Povekedwa
zibangiri zagolide ndi ngale; Silika
ndicho chovala chawo m'menemo.
34. Ndipo adzanena
(pakuthokoza kwawo):
"Kutamandidwa konse nkwa
Mulungu Amene watichotsera
madandaulo; Ndithu Mbuye wathu
Ngokhululuka Kwambiri,
Ngothokoza kwabasi.
35. "Yemwe, chifukwa cha
ubwino Wake, Watikhazika
m'nyumba yamuyaya; M'menemo
mavuto satikhudza, Ndiponso
m'menemo kutopa Sikutikhudza".
36. Koma amene
sadakhulupirire, wawo Ndi moto
wa Jahannama Sikudzaweruzidwa
kwa iwo kuti afe, Ngakhale
chilango chake
Sichidzachepetsedwa pa iwo. Umo
Ndimmene tikumlipirira aliyense
wokanira (Mtendere wa Mulungu).
37. Ndipo m'menemo iwo
adzakuwa (adzalira uku Akunena):
"Mbuye wathu! Titulutseni
&$$ti&2a$k&
9*99'" i*'. > &' 19 9 ~9} '< 9 9{'
Surat 35. Fatir
Juzu 22
933
XT *jJH
To ^\3 5jj-^
(M'moto ndi kutibweza padziko
Lapansi); tikachita ntchito
zabwino, Osati zija tinkachita"
(Mulungu Adzawauza): "Kodi
sitidakupatseni Moyo wokwanira
wotheka kukumbuka Kwa
wokumbuka? Ndiponso Mchenjezi
Adakudzerani. Choncho lawani
(Chilango). Ndipo anthu ochita
zoipa Alibe mpulumutsi."
38. Ndithu, Mulungu Ngodziwa
zobisika Zakumwamba ndi za
pansi. lye Ngodziwa kwambiri Za
m'zifuwa.
39. lye ndi Yemwe wakuchitani
kukhala Osiyirana padziko lapansi
(akufa Ena, ena nkulowa m'malo
mwawo). Ndipo amene
sadakhulupirire, kuipa kwa
Kusakhulupirirako kuli kwa lye
mwini. Ndipo kusakhulupirira kwa
Osakhulupirira sikuwaonjezera
Chilichonse kwa Mbuye wawo,
komaNkwiyo basi. Ndiponso
Kusakhulupirira kwa
osakhulupirira Sikuwaonjezera
chilichonse, koma Kutayika basi.
40. Nena: "Kodi mwawaona
aphatikizi Anu (awa) amene
mukuwapembedza M'malo mwa
Mulungu? Tandionetsani,
Ndimbali iti yanthaka adalenga;
Kapena iwo ali ndi gawo
m'thambo; (Gawo lakulenga
thambo?) Kapena Tidawapatsa
&
<$&<&<&&$#
Siirat 35. Fatir
Juzu 22
934
yy tji-»
To ^»13 5jj~*
Buku (Qur'an iyi Isadadze) kotero
kuti ali ndi umboni Wapoyera
wochokera m'menemo
(Wotsimikizira chipembedzo
chawo Chamafano?) Koma ochita
zoipa Salonjezana ena kwa ena
china chake Koma zachinyengo basi.
41. Ndithu, Mulungu
amachirikiza thambo Ndi nthaka
kuti zisachoke. Ndipo ngati
Zitachoka, palibe aliyense amene
Angazigwire kupatula lye. Ndithu,
lye Ngoleza; Ngokhululuka
kwabasi.
42. Ndipo (awa osakhulupirira,
kale) Adalumbirira Mulungu,
kulumbira Kwawo kwakukulu,
kuti ngati Adzawadzera mchenjezi,
adzakhala Oongoka kuposa
mbadwo uliwonse. Koma pamene
mchenjezi adawadzera, Palibe
chilichonse chidaonjezeka kwa
Iwo, koma kukana (choonadicho).
43. Chifukwa cha kudzikweza
padziko ndi Kuchita chiwembu
choipa. Ndipo chiwembu Choipa
sichingamtsikire aliyense koma
Mwini (yemwe) wachitayo. Kodi
Akuyembekeza china chosakhala
Machitidwe (a Mulungu) amene
Adawapititsa pa anthu akale.
Koma Supeza kusintha pa
machitidwe a Mulungu. Ndipo
supeza kutembenuka pa
Machitidwe a Mulungu.
Surat 35. Fatir
Juzu 22
935
YY *>»
TO ^kl3 5jj-*»
44. Kodi sadayende padziko
nkuona Momwe adalili mathero a
omwe adali Patsogolo pawo?
Ndipo adali anyonga Kwambiri
kuposa iwo? Ndipo palibe chinthu
Chonkanika Mulungu kumwamba
ndi Pansi. Ndithudi lye Ngodziwa
Kwabasi Wokhoza.
45. Ndipo Mulungu
akadamalanga anthu chifukwa Cha
zomwe alakwa, sakadasiya
Pamwamba pake (nthaka)
chamoyo Chilichonse; koma lye
amawalekerera Mpaka nthawi
yomwe adaiikayo. Ndipo nthawi
yawo ikadzawadzera, (Pompo
adzalangidwa). Ndithu, Mulungu
akuwadziwa bwino Akapolo Ake.
a
Surat 36. Ya-Sin Juzu 22 I 936 I t X t£\ T*\ Jj 5j^
^5
SURAT YA-SIN XXXVI
Surayi yayamba ndikutchula malembo awiri omwe amapanga
mawu m'chiyankhulo cha Chiarabu. Ndipo yatsiriza pazimenezi
kuilumbirira Qur'an ponenetsa kuti Muhammad (Madalitso ndi
Mtendere zikhale naye) ndi mmodzi wa atumiki. Ndi kuti iye ali
panjira yolunjika yomwe yaikidwa ndi Qur'an imene
yavumbulutsidwa kwa iye kuchokera kwa Mwini mphamvu
zoposa ndi Wachifundo chambiri, kuti ndi Qur'aniyo achenjeze
anthu omwe makolo awo akale sadachenjezedwe.
Surayi ikupereka chithunzi cha otsutsa amene sapindula ndi
machenjezo. Ndipo ikunenetsa kuti kuchenjeza kumawapindulira
okhawo omwe ali ndi mitima yochenjezeka ndi yoopa mwini
chifundo chambiri.
Yanenanso kuti ndithu, Mulungu adzaukitsa akufa ndi kutinso
Iye akusunga zochita zonse za akapolo Ake.
Surayi ikuperekanso fanizo la osakhulupirira a m'Makka
lomwe likusonyeza poyera mkangano wa pakati pa ovomereza ndi
otsutsa ndi kunenetsa kwa ndithundithu mapeto a magulu awiriwa.
Komanso Surayi yakamba za zisonyezo za kukhoza kwa
Mulungu zomwe zingachititse wanzeru ndi wolingalira
kukhulupirira ndi kuopa chilango cha Chauta, chomwe chidzadza
modzidzimutsa pa tsiku lomwe mzimu uliwonse udzalipidwa
zimene udachita; anthu a ku munda wa mtendere adzasangalala.
Ndipo adzapeza chilichonse chimene adzachikhumba. Pomwe
anthu akumoto adzapirikitsidwa ku chifundo cha Mulungu ndi
kuponyedwa kumoto uku kukamwa kwawo kutatsekedwa, ziwalo
zawo zikuwaneneza pa zochimwa zawo.
Ndipo Mulungu akadafuna, akadasintha maonekedwe awo
pompano padziko lapansi. Iye ndi Yemwe amasintha amene
moyo wake watalika padziko lino lapansi kukhala nkhalamba
yopanda mphamvu ndi yochepekedwa nzeru.Ndipo Iye ndi
Amene adateteza Mneneri wake ku chikhalidwe chamisala ndi
Surat 36. Ya-Sin Juzu 22 937 Y Y *>i r 1 J4 hf
kuti sadamphunzitse kulakatula nyimbo zopeka. Ndipo
sikoyenera kwa iye kukhala mlakatuli wa nyimbo zopeka.
Surayi ikunenetsanso kuti Mulungu adagonjetsa nyama kuti
zitumikire anthu ndi kuzikwera. Koma iwo mmalo mothokoza
Mulungu akupembedza milungu yosakhoza chilichonse.
Popitiriza Surayi, ikukumbutsa munthu chiyambi cha
chilengedwe chake ponenetsa kuti chilengedwe chake
chidachokera kumadzi opanda pake. Koma akakula amakhala
mwini makani zedi potsutsa zouka ku imfa, chikhalirecho akuona
zodabwitsa zambiri za Mulungu.
Mulungu amatulutsa moto mumtengo momwemonso
mumakhala madzi. Iye adalenga thambo ndi nthaka yochindikala
ndi yophanuka. Kodi wotere angalephere kubwezera mafupa
mmalo mwake?
Iye akaftina chinthu, savutika pakuti chinthucho
chichitike.Amangoti: "chichitike". Ndipo chimachitikadi.
Mulungu Ngolemekezeka ndi kupatukana ndi machitidwe
operewera. Iye ali ndi mphamvu pa chilichonse. Ndipo kwa Iye
ndi kobwerera zonse.
Surat 36. Ya-Sin Juzu 22 938 I Y Y «-j*-i
Y"l J^ 3j>-»
£«ra* Fa-Si/t XCm
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. KJ-Sf/i.
2. Ndikulumbira Qur'an (iyi
yomwe Yakonzedwa mwaluso)
yodzazidwa Ndi mawu anzeru.
3. Ndithu, iwe (Muhammad
{SAW}) Ndimmodzi wa atumiki
(amene Mulungu Adawatuma kwa
anthu kuti Akawasonyeze
chiongoko).
4. (Uli) panjira yolunjika.
5. (Qur'an iyi) nchivumbulutso
cha Mwini Mphamvu zoposa;
(palibe chokanika kwa lye)
Wachisoni,
6. Kuti uwachenjeze anthu
omwe atate Awo
sadachenjezedwe; choncho iwo
Ngoiwala (zomwe zili zofunika
Kuchitira Mulungu ndi
kudzichitira Okha pamodzi ndi
anthu ena).
7. Ndithu, mawu (onena za
chilango) Atsimikizika pa ambiri a
iwo; Poti iwo sakhulupirira.
8. Ndithu Ife taika magoli
m'makosi Mwawo ofika
kuzibwano, kotero kuti Mitu yawo
■ t "-■/- ^'~7:m
0&&\<&&\&\jt.
ijiT
#^pc&&&&
Surat 36. Ya-Sin Juzu 22
939
rr *>»
V% J+> *j>-»
yayang'anammwamba; (Siingathe
kutembenuka ndi kuyang'ana).
9. Ndipo tawaikira
Chotsekereza patsogolo pawo ndi
Chotsekereza pambuyo pawo,
Ndipo maso awo tawaphimba, tero
Iwo saona (zapatsogolo ndi
pambuyo Pawo).
10. Ndipo kwa iwo
nchimodzimodzi, Uwachenjeze
ngakhale usawachenjeze
Sangakhulupirire.
11. Ndithu, kuchenjeza kwako
Kupindulira amene watsatira
Qur'an ndi kumuopa (Mulungu)
Wachifundo ngakhale sakumuona.
Wotere muuze nkhani yabwino ya
Chikhululuko (chochokera kwa
Mulungu pa machimo Ake) ndi
malipiro aulemu.
12. Ndithu, Ife tidzaukitsa
akufa, Ndipo tikulemba zimene
atsogoza (M'dziko lapansi
m'zochita zawo) Ndi zomwe
amasiya pambuyo (atafa,
Zonkerankera mtsogolo), ndipo
Chinthu chilichonse tachilemba
M'kaundula wopenyeka
(wofotokoza Chilichonse).
13. Ndipo atchulire, (iwe
Mneneri) Nkhani ya eni mudzi
pamene Atumiki (A Mulungu)
adaudzera mudziwo (kuti
Akaongole eni mudziwo).
' 9? \,7Ci
fu^irl**y^^<^^
<• 9. \ 9 *9<*mU *tb"h9}"&h'
9 i*
Surat 36. Ya-Sin Juzu 22 940 Y Y *>»
Y"1 J*t 5j>-»
14. Pamene tidatumiza atumiki
awiri kwa Iwo adawatsutsa; ndipo
tidawalimbika Iwo (awiriwo)
potumiza wachitatu. (Atumiki
atatuwo) adati: "Ife Tatumidwa
kwa inu."
15. (Eni mudzi) adati: "Inu ndi
anthu Ngati ife; (Mulungu)
Wachifundo Chambiri
sadavumbulutse chilichonse (Kwa
munthu); inu simuli kanthu koma
Mukunena bodza."
16. (Atumiki) adati: "Mbuye
wathu (Amene watituma kwa inu)
akudziwa Kuti ife ndi otumidwadi
kwa inu.
17. Ndipo palibe china pa ife,
koma Kufikitsa kwachimvekere
uthenga (Wa Mulungu)."
18. (Eni mudzi) adati: "Ife
tapeza Tsoka chifukwa cha inu:
Ngati Simusiya (ulaliki wanuwo
wofuna Kutichotsa ku
chipembedzo chathu) Tikugendani
ndi miyala; ndipo Kuchokera kwa
ife chikupezani Chilango chowawa."
19. (Atumiki) adati: "Tsoka
lanu Lili ndi inu (chifukwa Cha
kukana kwanu ndi kupitiriza
Kupembedza mafano). Kodi
Mukakumbutsidwa (ndi mawu
omwe M'kati mwake muli
mtendere wanu Mukuti
takudzetserani masoka; ndi
Siirat 36. Ya-Sin
Juzu 23
941 tr*j*-»
Y"1 J^i 3j>-»
Kumatiopseza ndi chilango
chowawa?) Koma inu ndi anthu
olumpha malire".
20. Kenako munthu adadza
akuthamanga Kuchokera
kumalekezero a mzindawo (Ndipo)
adati: "E, inu anthu anga! Atsateni
atumikiwa.
21. Atsateni omwe
sakupemphani malipiro
(Pakukulangizani kwawo), Ndipo
iwo ngoongoka.
22. Kodi nchiyani
chingandiletse ine Kupembedza
Yemwe adandilenga? Ndipo kwa
lye ndi komwe inu nonse
Mudzabwerera.
23. Kodi ndidzipangire milungu
Kusiya lye (Mulungu) ?
Chipulumutso chawo
Sichingandipindulire chilichonse
Ngati (Mulungu) Wachifundo
Chambiri atafuna kundichitira
Zoipa; Ndipo siingandipulumutse.
24. Ndithu, ine ngati nditatero
ndiye kuti Ndili mchisokero
Choonekera poyera.
25. Ndithu ine ndakhulupirira
Mbuye wanu Choncho ndimvereni."
26. Kudanenedwa (kwa iye):
"Lowa M'munda wa Mtendere."
Iye adati: "Ha! Anthu anga,
Akadadziwa!
Surat 36. Ya-Sin Juzu 23 942 TT^i
*"* Or* 5 JJ~*
27. Momwe Mbuye wanga
wandikhululukira Ndikundichita
kukhala mmodzi wa Opatsidwa
ulemu (akadakhulupirira)"
28. Ndipo anthu ake
sitidawatsitsire ankhondo
Ochokera kumwamba pambuyo
pake (Kuti awaononge). Ndipo
pachizolowezi chathu sititsitsa
(ankhondo Kumwamba tikafuna
kuononga, koma Mngelo mmodzi
amakwanira).
29. (Kuonongeka kwawo)
kudali mkuwe Umodzi , ndipo
nthawi Yomweyo adali akufa (izi
zidachitika Pamene Jiburil
adawakuwira Mkuwe
wamphamvu).
30. Ha! Nzodandaulitsa kwa
Anthu! Palibe pamene Mtumiki
adawadzera popanda Kumchitira
chipongwe (ndi kukana Kumtsata)!
31. Kodi sadalingalire za
mibadwo Yambirimbiri imene
tidaiononga Patsogolo pawo?
Ndipo iwo Sangabwererenso kwa
iwo.
32. Ndipo zolengedwa zonse
Zidzaonekera kwa Ife
33. Ndipo chisonyezo chawo
Ndi nthaka ya chilala; Timaiukitsa
(ndi madzi) ndi kutulutsa
M'menemo njere, Zomwe zina
mwa izo amadya.
®^^(^^S®QI^^
®t
S99 9^9 9ft ?9?'
\&&2
®&^%f&t$&
Surat 36. Ya-Sin Juzu 23 943 YT *>i
T"V Jh »j>-
,<"SM '* t'i 9 ' K 9 '
rA ^«^(«tej«<a»os>
34. Ndipo tapanga m'menemo
minda Ya kanjedza ndi mpesa;
Ndipo tatulutsa m'menemo
akasupe.
35. Kuti azidya zipatso zake
pomwe Sizidapangidwe ndi manja
awo. Kodi bwanji sathokoza
(Mulungu)?
36. Alemekezeke (Mulungu),
Amene adalenga zinthu zonse,
chachimuna ndi Chachikazi,
kuchokera m'zimene Nthaka
ikutulutsa, ndi iwo omwe Ndi zina
zimene (anthu) sakudziwa.
37. Ndiponso chisonyezo
chawo Ndiusiku. M'menemo
timachotsamo Usana (womwe
umabisa usiku), ndipo (Anthu)
amangozindikira ali mumdima;
38. Ndipo dzuwa; limayenda
m'njira Ndi m'nthawi yake imene
Idakonzedwa kwa ilo. Chikonzero
Chimenecho ncha Wamphamvu
zoposa, Wodziwa kwambiri.
39. Ndiponso mwezi;
tidaukonzera malo Oimirapo
mpaka kukafika pomwe
Umabwerera ndi kukhala wochepa
Ndi wokhota monga nthambi ya
Mtengo wa kanjedza, youma
komanso Yokhota. 1
1 Ndime iyi ikufotokoza za kayendedwe ka mwezi kuti adaupangira malo 28
oimirapo. Umayamba pamalo woyamba uli wochepa ndi wokhota. Ndipo
umanka nukula kuchoka pa malo ena nkufika pa malo ena mpaka kukafika
Surat 36. Ya-Sin
Juzu 23
944 I tr^i
y^ j^ 5 jj--
40. Nkosatheka kwa dzuwa
kukumana ndi Mwezi (njira yake);
nawonso Usiku sungathe
kupambana usana (Pakudza nthawi
yausana isadathe,Koma
zimasinthana). Ndipo chilichonse
Mwa izo chimasambira m' njira
Yake (imene Mulungu
adachikonzera).
41. Ndiponso pali chisonyezo
kwa iwo (Chosonyeza madalitso
Athu pa Iwo). Ndithu, tidaukweza
mtundu Wawo mchombo
chodzazidwa (ndi Zonse zamoyo);
42. Ndipo tidawapangira
chonga icho Chomwe
akuchikwera. '
43. Ndipo ngati titafuna tikhoza
kuwamiza M'madzi, ndipo
sangapezeke Wowathandiza,
ndiponso Sangapulumutsidwe.
44. Koma (sitikuwamiza)
chifukwa cha Chifundo Chathu pa
iwo ndi kuti Asangalale kufikira
nthawi yawo (Yofera).
45. Ndipo kukanenedwa kwa
iwo: "Opani zomwe ziri patsogolo
Panu ndi zomwe ziri Pambuyo
<$ti^32S*fi36
@ gM,<&&P®z
© i^^^^^C^\
pomwe umakhala wokwanira mkuwala ndi m'maonekedwe ake. Pamenepa
mpamalo a 14. Tsono kuchoka apa, umayamba kuchepa pang'onopang'ono
ndi kubisika mpaka utafika pa malo a 28 pomwe umabisikiratu wonse.
Kayendedwe ka mwezi ndiko kamazindikiritsa anthu kutha kwa mwezi ndi
chaka, pomwe kayendedwe ka dzuwa kamazindikiritsa anthu kutha kwa tsiku.
1 Mulungu ndi Yemwe adapanga zombo ngakhale kuti zidapangidwa ndi
manja a anthu, chifukwa lye ndi Amene adaphunzitsa anthu kupanga zombozo.
Surat 36. Ya-Sin Juzu 23 I 945 I rr *>i
fl J^ «j>-»
panukuti muchitiridwe
Chifundo." (Iwo akunyoza
Malangizowo).
46. Ndipo palibe chisonyezo
chilichonse Mwazisonyezo za
Mbuye wawo (zosonyeza Umodzi
Wake ndi kukhoza Kwake)
Chomwe chidawadzera popanda
Kuchinyoza ndi kuchikana.
47. Ndipo kukanenedwa kwa
iwo: "Patsani (aumphawi) zimene
Mulungu wakupatsani,"
Osakhulupirira amanena kwa
Okhulupirira: "Kodi tidyetse
Yemwe Mulungu akadafuna
Akadamdyetsa; (titsutsane ndi
cholinga Cha Mulungu)? Ndithu,
inu simuli Kanthu koma muli
m'kusokera Koonekeratu."
48. Ndipo akunena
(mwachipongwe kwa
Okhulupirira): "Kodi lonjezo ili
(Lakudza kwa chiweruziro),
Lidzachitika liti, ngati mukunena
Zoona?"
49. Palibe chimene
akuyembekeza, koma Ndi mkuwe
umodzi womwe Udzawamaliza
mwadzidzidzi uku iwo
Akukangana.
50. Ndipo sangathe kuuza wina
mawu Pachinthu, ndiponso sangathe
Kubwerera ku maanja awo.
Surat 36. Ya-Sin
Juzu 23
946
tr^i
?"l Jri s jj~»
51. Ndipo lipenga lidzaimbidwa
(loukitsa Akufa); iwo
adzangozindikira Akutuluka
m'manda kunka Kwa Mbuye
wawo uku akuthamanga.
52. Adzati: "Kalanga ife! Kodi
Ndani watidzutsa pogona pathu?"
(Adzawauza) "Izi ndi zimene
Adalonjeza (Mulungu),
Wachifundo Chambiri ndi zimene
adanena Atumiki moona."
53. Sipadzakhala (china) koma
mkuwe Umodzi basi;
adzangozindikira Iwo onse
atabweretsedwa patsogolo Pathu.
54. "Ndipo mzimu uliwonse
lero Suponderezedwa pa
chilichonse. Ndipo mulipidwa pa
zokhazo Munkachita."
55. Ndithu, anthu aku munda
wa mtendere Lero akhala
wotanganidwa ndi Chisangalalo.
56. Iwo ndi akazi awo akhala
M'mithunzi uku atatsamira
mipando (Ya mtengo
wapamwamba;)
57. M'menemo apeza (mtundu
Uliwonse) wazipatso ndiponso
Apeza chilichonse chimene
Akuchifuna.
58. "Mtendere (pa iwo)!"
Limeneli Ndi liwu lochokera kwa
Mbuye (Wawo), Wachisoni.
Surat 36. Ya-Sin Juzu 23 947 Y T *>i
?^ u~>- 5 J> -
59. "Ndipo dzipatuleni lero, inu
oipa!
60. Kodi sindidakulangizeni, E,
inu Ana a Adamu kuti
musapembedze Satana; ndithu, iye
ndi mdani Woonekera kwa inu.
61. Ndikuti ndipembedzeni Ine;
Imeneyi ndi njira yolunjika?
62. Ndithu, (satana)
adasokeretsa Anthu ambiri mwa
inu. Kodi Simumaganizira
mwanzeru?
63. Iyi ndi Jahena yomwe
Mumalonj ezedwa.
64. Iloweni lero, chifukwa cha
Kunkana kwanu (Mulungu).
65. Lero titseka kukamwa
kwawo. Ndipo manja awo
atiyankhula Ndipo miyendo yawo
ichitira Umboni pa zomwe
amachita."
66. Ndipo tikadafuna,
tikadafafaniza maso Awo; ndipo
akadakhala akuthamangira njira;
koma Akadapenya chotani?
67. Ndipo tikadafuna,
tikadawasintha Kukhala ndi
maonekedwe a nyama Pamalo
pawo pomwepo (pamene adali),
Kotero kuti sakadatha kuyenda
(Kunka patsogolo) ngakhale
Kubwerera pambuyo.
**g&$&£&&i i
Surat 36. Ya-Sin
Juzu 23
948 tr*>»
^ J^ 5 jj^
68. Ndipo amene
tikumtalikitsira moyo Wake,
timam'bwezeranso pambuyo
M'chilengedwe chake (ndi kukhala
Ngati mwana). Kodi bwanji
saganizira Mwanzeru?
69. Ndipo sitidamphunzitse
(Mtumiki {SAW})Ndakatulo,
ndipo nkosayenera kwa lye
(kukhala mlakatuli). Qur'an
Sichina, koma ndichikumbutso ndi
Buku lomwe likulongosola
Chilichonse,
70. Kuti awachenjeze amene ali
moyo, Ndi kuti litsimikizike liwu
(Lachilango) pa osakhulupirira.
71. Kodi saona kuti Ife
tawalengera Nyama, m'zimene
manja Athu akonza, Zomwe iwo
akuti nzawo,
72. Ndi kuti tazichita kukhala
Zowatumikira? Zina mwa izo
Amazikwerapo; ndipo zina mwa
Izo amazidya.
73. Ndipo m'menemo
(m' nyama) muli Zowathandiza
(zambiri) ndiponso Zakumwa.
Nanga Bwanji sathokoza?
74. Ndipo adzipangira milungu
(Yabodza) kusiya Mulungu
(weniweni) Kuti athandizidwe nayo.
75. (Koma) siingathe
kuwathandiza; Ndipo iwo (kwa
X"
<¥^&&^v%&»M
@ om$^>>w&%>
®6i^H^^^^ctf!^£
<%^^%&&&$
Surat 36. Ya-Sin Juzu 23 I 949 I rr *>
^ Jr* *jy*
milunguyo) ndi Asilikali amene
akonzedwa Kulondera (mafanowo
ndi Kuwatumikira).
76. Mawu awo (onyoza
Mulungu ndi Okutsutsa iwe)
asakudandaulitse. Ndithu, Ife
tikudziwa zimene Akubisa ndi
zimene akuzionetsera Poyera.
77. Kodi munthu sazindikira
kuti Ife Tidamulenga ndi dontho la
umuna? Koma iye wakhala
Wotsutsa woonekera.
78. Ndipo akutiponyera fanizo
(Lotsutsa kukhoza Kwathu
kuukitsa Akufa) ndi kuiwala
chilengedwe Chake (chochokera
kumadzi opanda Pake). Akunena:
"Ndani angaukitse Mafupa pomwe
ali ofumbwa?"
79. Nena: "Adzawaukitsa
Yemwe Adawalenga panthawi
yoyamba. Ndipo Iye Ngodziwa
kalengedwe ka mtundu Uliwonse.
80. Yemwe adakupangirani
moto Kuchokera mumtengo
wauwisi; Kenako inu mumakoleza
moto M'menemo.
81. Kodi Yemwe adalenga
thambo ndi Nthaka (mukuganiza
kuti) siwokhoza Kuwalenga (iwo
kachiwiri) monga Momwe alili?
Inde! Iye ndiMlengi Wamkulu,
Wodziwa kwambiri!
'^mB&®&
j^psS^MJSi^SSSi
Zft'lV <
(££0i&^l&&2%
©
(99 s'^"\\'
v&<
SI
<Sx
Surat 36. Ya-Sin Juzu 23 950 T T *>i
V"\ Jri «j>-
82. Ndithu, machitidwe Ake
akafuna Kuti chinthu chichitike,
amangonena Kwa icho: "Chitika!"
Ndipo chimachitika (Nthawi
yomweyo).
83. Kotero alemekezeke
Yemwe m'manja Mwake muli
ulamuliro pachinthu Chilichonse;
ndipo kwa lye (ndiko)
Mudzabwerera nonse."
e^^SBBss^awefii
t£$a$& «f^g#$tef52
Surat 37. As-Saffat Juzu 23
951
rrfrjJH rv oiBUaJi djj-
PgP"
SURAT AS-SAFFAT XXXVII W
J^§
Sura iyi yayamba ndi kulumbirira zina mwa zolengedwa za
Mulungu zomwe zimakhala m'mizere ndi zomwe zimakalipa
ndi kulakatula kuti Mulungu ndi mmodzi. Ndipo lye ndi Mbuye
wa thambo ndi nthaka ndi zomwe zili pakati pake Mbuye wa
kuvuma konse ndi kuzambwe, Yemwe adakongoletsa thambo
lapafupi ndi dziko lapansi ndi nyenyezi. Ndipo adalichita
thambolo kukhala lotetezedwa kwa otuluka m'chilamulo cha
Chauta.
Surayi, pambuyo ponenetsa za umodzi wa Mulungu,
yanenetsanso za kuuka ku imfa. Ndipo yaopseza okaika za
kuukako ponena kuti adzangodzidzimuka akupenya.
Yalongosolanso zisonyezo zomwe zikusonyeza kutheka
kwake kwa kuchitika zimenezo. Ndipo iwo akadzaliona tsiku
limenelo adzanena: "Ha! Hi nditsiku la Malipiro." Ndipo
kudzanenedwa kwa iwo: "Inde, ili nditsiku la chiweruziro
lorn we mumalitsutsa."
Achinyengo adzasonkhanitsidwa pamodzi ndi zimene
amazipembedza. Ndipo adzayamba kufunsana ndi kukangana
pakati pawo, uku onse ali mkati mwa Jahena. Ndithu, iwo
adadzikweza posalabadira umodzi wa Mulungu. Ndipo amatcha
aneneri awo kuti ngamisala, chikhalirecho adawadzera ndi
choonadi. Koma okhulupirira adzakhala mumtendere wochuluka
wa Mulungu. Adzakhalanso akusuzumira ku Jahena kuti aone
anthu oipa. Ndipo adzawaona ali m'katikati mwa moto.
Pamenepo iwo adzathokoza Mulungu chifukwa chowapatsa
chisomo cha kutetezedwa ndi kupulumuka kuzimene amawaitanira,
zosokera.
Komanso Surayi ikusimba za malo a osalungama ndi malo a
olungama. Ndipo yapitiriza kusimba nkhani ya aneneri a
Mulungu ncholinga chotonthoza Mtumiki Muhammad (SAW)
pamavuto omwe amapezana nawo. Nkutinso zikhale maphunziro
Siirat 37. As-Saffat Juzu 23
952
TT;>l rV otiUJl 5jj-
kwa anthu osakhulupirirawo.
Ndipo Surayi yatsutsa zomwe opembedza mafano ankanena
kuti ana achikazi nga Chauta, pomwe achimuna ndiwo awo,
kutinso angelo ndi akazi. Komanso kuti pakati pa lye ndi
ziwanda pali chibale.
Mulungu apatukane ndi zimene akusimbazo! Anthu Ake
ndiwo othangatidwa. Ndipo makamu Ake ankhondo ndiwo
opambana.
Ndipo Surayi yamaliza ndi kulemekeza Mulungu ndi
kumpatula ku zomwe akumufanizira nazo.
Surat 37. As-Saffat Juzu 23 I 953 rr »>■! rv otsuJi i^
SuratAs- Saffat XXXVII
¥
t»j& " >#:
^
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Ndikulumbira (angelo)
amene Amandanda m'mizere
yondondozana, (Popembedza ndi
kugonjera Mbuye Wawo).
2. Ndi omwe amaletsa zoipa.
3. Ndi omwe amalalika ulaliki
(wa Mulungu ndi kumtamanda
Mochulukira).
4. Ndithu, Mulungu wanu
ndimmodzi Basi.
5. Mbuye wathambo ndi nthaka,
ndi Zapakati pake; ndiponso
Mbuye Wa ku vuma konse.
6. Ndithu, tidalikongoletsa
thambo Lapafupi (ndi inu) ndi
chokongoletsa Cha nyenyezi
(zowala).
7. Ndi kuti lisungidwe ku satana
aliyense Wogalukira (lamulo la
Mulungu),
8. Kuti asamvere (zomwe
zikunenedwa Ndi) zolengedwa
zolemekezeka (Angelo). Ndipo
akugendedwa (ndi Kupirikitsidwa)
mbali zonse,
9. Kuthamangitsidwa
mwamphamvu; Ndipo chilango
q^i^i^u ^v
9i^(iil)ij
&$££$&&£
H&&&S&
tjUvfe
Surat 37. As-Saffat Juzu 23
954
xr*j*-» rvoiiuiUj^
chonkerankera Patsogolo chili pa
iwo,
10. Kupatula amene
wazembetsa mawu (Akumwamba),
ndipo chikumtsatira lye chenje cha
moto chowala kwambiri.
11. Tawafunsa, (otsutsa Zouka
ku imfa): "Kodi iwo ngovuta
Kuwalenga kuposa zimene
tidalenga, (Monga: thambo,
nthaka, nyenyezi Ndi zina
zotere)?" Ndithu, iwo Tidawalenga
kuchokera ku dongo Lonyata,
12. Koma iwe (Mneneri)
ukudabwa (za Kutsutsa kwawo
kuuka ku imfa pomwe Zisonyezo
zilipo zambirimbiri), Ndipo
akukuchitira chipongwe (Kudabwa
kwako).
13. Ndipo akalalikiridwa,
salalikirika,
14. Ndipo akachiona
chisonyezo (Chosonyeza kukhoza
kwa Mulungu,) Amachichitira
chipongwe,
15. Ndipo osakhulupirira
amanena "Palibe chilipo apa, koma
ndi matsenga Woonekera poyera.
16. Kodi tikadzafa ndi
kusanduka Fumbi ndi mafupa,
tidzatulutsidwanso (Kuchokera
m'mandatili amoyo)?
17. Pamodzi ndi atate athu akale?"
*■
K^V&2\o&£&
ao-.v*
%#>£'. Zffi
®&m$$
Surat 37. As-Saffat Juzu 23
955
rr s-j*-i rv oi3Ua3i 5jj^
18. Nena, (iwe Mneneri): "Inde
(Mudzaukitsidwa inu pamodzi ndi
Atate anu) uku inu muli
onyozeka."
19. Ndithu, (kuukako)
ndimkuwe Umodzi
adzangodzidzimuka Ali moyo,
akuyang'ana.
20. Ndipo adzanena (okanawo):
"Kalangalfe! Kuonongeka
nkwathu! Hi Nditsiku lija lamalipiro!
21. (Adzawauza): "Hi nditsiku
lachiweruzo Lomwe mumalitsutsa
lija.
22. (Kudzanenedwa kwa
angero): "Asonkhanitseni amene
adali Osalungama pamodzi ndi
akazi Awo (okana Mulungu) ndi
milungu Yawo imene
amaipembedza,
23. Kusiya Mulungu, ndipo
asonyezeni Njira ya ku Jahena.
24. Koma aimikeni pano
chifukwa iwo Afunsidwa (za
chikhulupiriro Chawo ndi zochita
zawo):
25. "Kodi nchifukwa ninji inu
(opembedza Mafano)
simukupulumutsana (monga
Mumanenera padziko lapansi kuti
Mudzapulumut sana) ?
26. Koma iwo adzagonjera Ndi
kudzipereka (ku lamulo la Mulungu);
%&#&*#
^asw^fcKiffi
a '™»® $s
*c^fjStoA^K&
*&®p;
%&&%$&&
Surat 37. As-Saffat Juzu 23 I 956 I tr *>i TV oiauaJi Sj^
27. Ndipo adzatembenukirana
ndi Kuyamba kufunsana Ndi
kudzudzulana.
28. Ndipo (ofooka) adzanena
(kwa Odzikweza): "Inu
mumatidzera Kumbali komwe
timakuganizira kuti nkwabwino.
(Ndi kutichotsako Kunka nafe ku
njira yopotoka).
29. (Odzikweza) adzayankha:
"Koma Simudali okhulupirira.
30. Ndipo tidalibe nyonga
zokuponderezerani Inu, koma
mudali anthu opyola Malire (ndi
kutuluka ku choonadi Cha
Mulungu).
31. Choncho mawu a Mbuye
wathu (Onena za chilango)
atsimikizika Pa ife; ndithu, ife
tichilawa (Chilango).
32. Tidakusokeretsani; nafenso
tidali Osokera. (Choncho
musatidzudzule) . "
33. Ndithu,iwo akathandizana
chilango tsiku Limenelo (la
chiweruziro).
34. Ndithu, (chilango chonga
chimenecho) Ndimomwe
timawachitira Olakwira (Mulungu).
35. Ndithu iwo ankati
akauzidwa kuti palibe
Wopembedzedwa mwa choonadi
koma Mulungu ankadzitukumula
nsKa#*f«SPB
m£&&£&si
®w^OTr^tl?e
Surat 37. As-Saffat Juzu 23
957 tr *>» TV oiduJi 5j^
36. Ndipo ankanena: "Kodi ife
tisiye Kupembedza milungu yathu
chiftikwa Cha zonena za mlakatuli,
wopenga?"
37. Iyayi koma adawadzera ndi
choonadi (Mthenga wawo
Muhammad yemwe Siwamisala
kapena wolakatula Zopeka) ndipo
adawatsimikizira za Atumiki.
38. Ndithu, inu (osakhulupirira)
Mudzalawa chilango chowawa;
39. Ndipo mudzalipidwa
zokhazo Zimene mumachita;
40. Kupatula akapolo a
Mulungu Oyeretsedwa,
41. Kwa iwo kuli zopatsidwa
zodziwika (Ndi Mbuye wawo
Mulungu),
42. Zipatso (zamtundu
uliwonse); Ndipo iwo adzalandira
ulemu (Waukulu),
43. M'minda ya mtendere,
44. Adzakhala pa mabedi (a
mtengo Wapatali) uku
akuyang' anizana;
45. Uku zikuwazungulira zikho
Zodzazidwa ndi zakumwa
Zochokera m'kasupe woyenda
Nthawi zonse,
46. Woyera, wokoma kwa
wakumwa (Zakumwazo),
^8&m&&sk>$&
>j&
%&$\<3&i<$\s&. 35
Siirat 37. As-Saffat Juzu 23
958 rr *jA-i rv oiiuaJi Sj^
47. Mzakumwazo mulibe
zopweteketsa Mutu kwa ozimwa
ndiponso iwo Sadzaledzera nazo.
48. Ndipo kwa iwo kudzakhala
akazi Ophanuka maso, okongola;
oyang'ana Iwo okha.
49. Onga ngati dzira (la
nthiwatiwa) Losungidwa
(m'mapiko).
50. Ndipo adzayang'anizana ndi
Kuyamba kufunsana (pakati pawo.)
51. Adzanena wonena mmodzi
wa iwo:"Ine Ndidali ndimnzanga
(wopembedza Mafano amene
amatsutsana Nane za chipembedzo
ndi Zophunzitsa za Qur'an
yolemekezeka).
52. Yemwe amandiuza: "Kodi
iwe ndiwe Mmodzi wa ovomereza?
53. Zakuti tikadzafa ndi
kusanduka Fumbi ndi mafupa,
(tidzaukanso) Ndi kulandira
malipiro (pa zochita Zathu)?"
54. (Wokhulupirira) adzanena
(kwa Anzake: "Inu anthu a
kumtendere) Kodi
simungasuzumire (kumoto kuti
Nawe umuone mnzako uja)?
55. Adzayang'ana ndipo
Adzamuona ali Mkatikati mwa moto.
56. Adzanena: "Ndikulumbirira
Mulungu! Udatsala pang'ono kuti
Surat 37. As-Saffat Juzu 23
959
ir tj*r\ rv oiiu^Ji oj^-
Undiononge (ndikadakuvomera
paja Padziko lapansi).
57. Ndipo pakadapanda
chisomo cha Mbuye Wanga,
ndikadakhala mmodzi mwa
Opezeka ku moto.
58. Kodi zili choncho kuti
sitidzafanso (tizingosangalala
m'munda wa mtendere),
59. Kupatula imfa yathu
yoyamba ija, Ndi kutinso ife
Sitilangidwa?"
60. Ndithu, izi (zimene
Mulungu waika M'munda wa
mtendere) ndiko Kupambana
kwakukulu.
61. (Pofuna kupeza) zonga
zimenezi ogwira Ntchito agwire.
62. Kodi zimenezo ndilo
phwando Labwino kapena mtengo
wa Zaqqum (wowawa kwambiri
Womwe anthu a kumoto azikadya)?
63. Ndithu, Ife taupanga
(mtengo Umenewu) kukhala
mayeso ndi Chilango cha anthu
ochimwa (Podzichitira okha
chinyengo ndi Kupembedza
mafano.)
64. Umenewu ndimtengo omwe
umatuluka Pakatikati pa Jahannama
(Adaulenga kuchokera kumoto).
65. Zipatso zake (Nzoipa) ngati
mitu ya Asatana.
&(j^ > &&£\
e&MmW2§
©,
\$M£ffi6W&
Surat 37. As-Saffat Juzu 23
960
tr*j±-i rv oibuoJi ojj-
66. Ndithu iwo akadya
mtengowo ndi Kudzaza mimba
zawo ndi zipatso zake (Pakuti
sakapeza chakudya china Kupatula
zipatso za mtengowo).
67. Komanso, ndithu, kuwawa
kwa Mtengowo kosakanikirana ndi
madzi Owira kudzakhala pa iwo.
68. Kenako ndithu, kobwerera
kwawo Ndi ku Jahena.
69. Ndithu, iwo adapeza atate
awo Ali osokera;
70. Ndipo iwonso
adawayendetsa kutsata Mapazi
awo (mothamanga).
71. Ndipo, ndithu, akale ambiri
Adasokera patsogolo pawo;
72. Ndipo, ndithu, tidatuma
Achenjezi kwa iwo.
73. Tapenya momwe adalili
mapeto a omwe adachenjezedwa.
74. Kupatula akapolo a
Mulungu, Oyeretsedwa (iwo
ndiwo anthu a ku Munda wa
Mtendere).
75. Ndithu, Nuhi adatiitana,
(ndipo Tidamuyankha mayankho
abwino) Taonani kukhala bwino
Ife Oyankha.
76. Ndipo tidampulumutsa iye
ndi Anthu ake kuvuto lalikulu,
&v£&3\?fir$tila&3
^\^mm;
Surat 37. As-Saffat Juzu 23
961
yt*jJh rv oialaJi ojj-»
77. Ndipo tidawachita adzukulu
ake kukhala Otsala (padziko, oipa
ataonongeka);
78. Ndipo tidamsiira mbiri
yabwino Kwa mibadwo yodza
pambuyo pake.
79. Mtendere ukhale pa Nuhi pa
zolengedwa Zonse.
80. Ndithu, umu ndimomwe Ife
tilipirira Ochita zabwino.
81. Ndithu iye ndi mmodzi
mwa akapolo Athu Amene
adatikhulupirira.
82. Kenako tidawamiza enawo.
83. Ndipo ndithu, Ibrahim adali
m'gulu Lake; (adayenda
mayendedwe ake).
84. Kumbuka pamene adadza
kwa Mbuye Wake ndi mtima
woyera, (wogonjera Malamulo).
85. Pomwe adanena kwa bambo
wake ndi Anthu ake:
"Mukupembedza chiyani?
86. Ha! milungu yopeka Kusiya
Mulungu, Ndi imene mukuifuna?
87. Kodi maganizo anu ngotani
pa Mbuye Wazolengedwa zonse?"
88. Ndipo adayang'ana
nyenyezi mozama.
89. Ndipo adanena: "Ine ndine
wodwala!"
9 flfi U X &KX'Z
^dPS^
efe^js
Surat 37. As-Saffat Juzu 23
962
vr tj*r\ rvoiduiiSj^
90. Choncho iwo adatembenuka
ndi kumsiya.
91. (Ibrahim) adapita mozemba
kumafano Awo, ndipo adawauza
(mwachipongwe:) "Bwanji
simukudya (chakudya chomwe
Chaikidwa patsogolo panupo)?
92. Bwanji simukuyankhula?"
93. Atatero adawatembenukira
ndi Kuwamenya (mwamphamvu)
ndi dzanja Lamanja.
94. (Pamene adamva eni
mafanowo) Adadza kwa iye
akuthamanga.
95. Anati: "Kodi mukupembedza
(miyala) Imene mwasema?
96. Chikhalirecho Mulungu
ndiye Adakulengani ndi zimene
mukuchita!"
97. (Iwo) adati: "Mmangireni
ng'anjo, Ndipo mponyeni
m'motowo."
98. Adafuna kumchita chiwembu
(kuti amuphe ndi moto), koma
tidawachita Kukhala onyozeka.
99. Ndipo (Ibrahim) adati:
"Ndithu ine Ndikupita kwa Mbuye
wanga Iye andiongolera.
100. O, Mbuye wanga!
Ndipatseni mwana Yemwe
adzakhale (mmodzi) mwa
Olungama!"
Surat 37. As-Saffat Juzu 23
963
tr*>i rvoiiuJioj^
101. Ndipo tidamuuza nkhani
yabwino Ya mwana wofatsa,
(Mwanayo ndi Ismaila).
102. Ndipo (adabadwa ndi
kuyamba kukula.) Pamene
adakwana msinkhu Woyenda
pamodzi ndi tate wake
Pochitachita za m'dziko (Ibrahim
Adayesedwa mayeso kupyolera
M'maloto omwe adalota). Adati:
"E, mwana wanga! Ine Kutulo
ndikuona maloto (oona Ochokera
kwa Mulungu omwe
Akundilamula) kuti ndikuzinge
(Monga nsembe yopereka Kwa
Mulungu). Nanga ukuti Bwanji?"
(Mwana wabwino) adanena:
"Bambo wanga! Kwaniritsani
chimene Mukulamulidwa. Ngati
Mulungu Afuna, mundipeza ndili
mmodzi Mwa opirira."
103. Pamene adagonjera onse
awiri (chofuna Cha Mulungu),
ndipo (Ibrahim) Adam'goneka
chakumphumi (Ndipo adatsimikiza
kumupha).
104. Ndipo tidamuitana: "E,
iwe Ibrahim.
105. Ndithu, wavomereza
maloto! (Choncho usamuphe
mwana wakoyo)." Umo ndi momwe
timawalipirira Ochita zabwino.
106. Ndithu,amenewa
Ndimayeso oonekera,
Q$03Cp[&
fys&3&
e^3S3tfto&
Surat 37. As-Saffat Juzu 23 964 tr *&\ TV oiauJi Sjj-
107. Ndipo tidampulumutsa
pompatsa nyama Yayikulu (yoti
apereke nsembe.)
108. Ndipo tidamsiira (mbiri
yabwino) Kwa anthu ena (amene
adadza Pambuyo pake).
109. Mtendere ukhale pa
Ibrahim!
110. M'menemo ndi momwe
timawalipirira Ochita zabwino.
111. Ndithu, iye adali mmodzi
mwa Akapolo Athu okhulupirira.
112. Ndiponso tidamuuza
nkhani yabwino (Yoti akhala ndi
mwana wotchedwa) Isihaqa;
mneneri; wam'gulu la Olungama.
113. Ndipo tidamdalitsa iye ndi
(mwana wake) Isihaqa; ndipo
m'mbumba ya awiriwa
Mudapezeka abwino ndi
odzichitira Zoipa owonekera.
114. Ndipo ndithu,
tidawachitira zabwino Musa ndi
Haruna, (powapatsa uneneri ndi
Madalitso ambiri).
115. Ndipo tidawapulumutsa
(awiriwa) Ndi anthu awo Ku vuto
lalikulu;
116. Ndipo tidawathangata
(powagonjetsera Adani awo),
ndipo iwo adali opambana.
4gtfid#G$
&&tetj&$&'j&
®j^&\<3^&ffi$&
&0$'M!&&jZ>
Surat 37. As-Saffat Juzu 23
965
Yr*jJi-l TV OlSUflJl «j^-
117. Ndipo tidawapatsa (Musa
ndi Haruna) Buku losonyeza
poyera (malamulo;)
118. Ndipo tidawaongolera ku
njira Yolunjika.
119. Ndiponso tidawasiira
(mbiri Yabwino) kwa anthu ena
(amene Adadza pambuyo pawo).
120. Mtendere ukhale pa Musa
ndi Haruna!
121. Ndithu umu ndi momwe
Ife Timawalipirira ochita zabwino.
122. Ndithu, awiriwa adali
m'gulu la Akapolo Athu
okhulupirira.
123. Ndipo ndithu, Iliyasa ndi
mmodzi wa Otumidwa.
124. (Kumbuka) pamene
adanena kwa anthu Ake:"Bwanji
Simuopa (Mulungu)?
125. Mukupembedza (fano
lotchedwa) Baala ndi kusiya
(kupembedza) Yemwe adalenga
zolengedwa M'kalengedwe
kabwino,
126. Mulungu, Mbuye Wanu
ndi Mbuye wa Atate anu akale?"
127. Koma adamtsutsa; ndithu,
iwo Adzaonekera (kumoto),
128. Kupatula akapolo a
Mulungu amene Ayeretsedwa (ndi
Mulungu).
©,
«"?. *J\i\i f * \' f *\
Surat 37. As-Saffat Juzu 23
966
rr*>i rv oi3Ua)i 5jj-
129. Ndipo tidamsiira (mbiri
yabwino) Kwa anthu ena (amene
adadza Pambuyo pake).
130. Mtendere ukhale pa Uiyasa!
131. Ndithu umo ndi mmene Ife
timawalipirira Ochita zabwino.
132. Ndithu, iye adali mmodzi
mwa Akapolo Athu okhulupirira.
133. Ndithu, Luti ndi mmodzi
wa otumidwa.
134. (Kumbuka) pamene
tidampulumutsa Iye ndi anthu ake
onse,
135. Kupatula nkhalamba
yachikazi; Idali mwa otsalira.
136. Kenako tidawaononga
enawo (omwe Adali oipa).
137. Ndithu, inu ( amzinda
wa Makka) Mumadutsa pa malo
pawopo m'mawa,
138. Ndi usiku. Kodi bwanji
simuzindikira?
139. Ndithu, Yunusu ndi
mmodzi wa otumidwa.
140. (Kumbuka) pamene
adathawira Mchombo
chodzazidwa (ndi katundu),
141. Choncho adachita mayere,
ndipo adali M'gulu la omgwera
(mayerewo).
®&rM*&&
ifj
®0#d6&&
•#RSJ#
Surat 37. As-Saffat Juzu 23
967
rr*>i rv oidUflii oj^
142. Choncho nsomba
Idammeza uku ali
Wodzudzulidwa.
143. Kukadapanda kuti iye adali
m'modzi Mwa otamanda ndi
kulemekeza Mulungu,
144. Akadakhala mmimba
mwake Mpaka tsiku loukitsidwa
Zolengedwa ku imfa).
145. Koma tidamponya Pa
gombe uku ali Wodwala,
146. Ndipo tidammeretsera
mmera wa ntundu Wa mankhaka.
147. Ndipo (atachira)
tidamtuma ku anthu Okwana zikwi
zana limodzi (100,000) Kapena
kupambana apa.
148. Ndipo adakhulupirira (ndi
kuvomereza Ulaliki wake);
choncho tidawapatsa Chisangalalo
kufikira nthawi (ya Imfa yawo).
149. Choncho afunse: "Kodi
Mbuye Wako ndiye woyenera ana
Achikazi, ndipo iwo, Achimuna?
(Pomwe iwo Akabereka mwana
wachikazi Amanyansidwa naye)"!
150. Kapena kuti tidalenga
Angelo kukhala Akazi, iwo akuona?
151. Chenjera ndi bodza
lawolo; ndithu, Iwo akunena:
152. "Mulungu wabereka."
Ndithu, iwo ndi Abodza.
Siirat 37. As-Saffat Juzu 23
968
tr^i rv oi3UaJUjj--
153. Kodi lye adasankha ana
achikazi kusiya Achimuna?
154. Kodi nchiyani chakupezani
(kuti Muweruze mopanda
chilungamo); Nanga mukuweruza
bwanji (zimenezi)?
155. Kodi bwanji
simukumbukira, (Mwaiwala
zisonyezo zake zodabwitsa Ndi
kupatukana kwake ndi zimenezo)?
156. Kapena inu muli ndi
umboni Woonekera (wochokera
kumwamba)?
157. Tabweretsani buku lanulo
(momwe Mwalembedwa zimenezi)
ngati Mukunena zoona.
158. Ndipo adapeka chibale
pakati pa lye (Mulungu) ndi
ziwanda; (pomwe Ziwanda
nzobisika kwa iwo). Ndithu,
Ziwanda zimadziwa kuti iwo
Osakhulupirira akaonekera (kwa
Mulungu kuti aweruzidwe)!
159. Walemekezeka Mulungu!
Ndi Kupatukana ndi zimene
Akumnamizira!
160. Koma akapolo a Mulungu
oyeretsedwa, (Ali kutali ndi
zimene akusimba
Osakhulupirirazi).
161. Ndithu, inu osakhulpirira
ndi zimene Mukuzipembedza
(kusiya Mulungu),
Surat 37. As-Saffat Juzu 23
969 tr^i rv oiduoji Sj^-
162. Ndi zimenezo
Simungamsokeretse aliyense.
163. Kupatula yemwe
(Mulungu adadziwa Kuti) ngolowa
ku Jahena.
164. Ndipo (Angelo adanena):
"Aliyense mwa ife ali ndi malo ake
Odziwika;
165. Ndipo ena mwa ife
ngondanda M'mizere (ya
mapemphero nthawi Zonse);
166. Ndipo ena mwa ife
ngolemekeza (Mulungu nthawi
zonse ndi Kumtamanda ndi
kumpatula ku zinthu Zosayenerana
ndi ulemerero wake)."
167. Ndipo (osakhulupirira)
ankati:
168. "Tikadakhala ndi Buku
monga lomwe Anthu akale adali
nalo,
169. Tikadakhala akapolo a
Mulungu, Oyeretsedwa."
170. Koma (pamene
lidawadzera Bukulo), Adalikana;
choncho posachedwa Adziwa
(zotsatira zake).
171. Ndipo ndithu, liwu lathu
lidatsogola kwa Akapolo athu
Otumidwa,
172. (Kuti) ndithu iwo
ngopulumutsidwa.
**
\&m
Surat 37. As-Saffat Juzu 23
970
rr*j*-» rvotfuiisj^-
173. Ndipo ndithu, asilikali
Athu ndi opambana.
174. Choncho, asiye kwa
Kanthawi kochepa,
175. Ndipo ingowayang'ana
basi; Posachedwapa aona!
176. Kodi chilango chathu
Akuchifulumizitsa?
177. Choncho chikadzatsika
pabwalo lawo, Udzakhala mmawa
woipa kwa Ochenjezedwa!
178. Ndipo asiye kwa Kanthawi
kochepa,
179. Ndipo ingowayang'ana
basi; Posachedwapa aona.
180. Mbuye wako, Mwini
Ulemerero, Wapatukana ndi
Zimene akumnamizira
(Osakhulupirira).
181. Ndipo mtendere ukhale pa
atumiki Onse.
182. Ndipo kuyamikidwa konse
nkwa Mulungu, Mbuye wa
zolengedwa Zonse.
:~ &S8L*&
Surat 38. Sad Juzu 23
971
TT *j£-l FA Jfi 5jj-*
Surayi ikupereka chinthunzi kwa ife cha makani a anthu
opembedza mafano pakutsutsa ulaliki wa Mtumiki (madalitso ndi
mtendere zikhale naye), ndi dumbo pokwiya ndi madalitso amene
Mulungu adampatsa pomuninkha uneneri ndi kumvumbulutsira
Qur'an. Ndipo yawayankha pamaganizo awo achabe.
Ndipo yafotokoza kuti chimene chawachititsa iwo kulimbana
ndi uthenga wa Mtumiki(SAW), ndikudzitukumula basi ndi
kukonda makani. Ndipo yafotokozanso kuti chikadawatsikira
chilango cha Chauta sibwenzi akumunenera Mtumiki wa
Mulungu zomwe akunenazo.
Mulungu waperekanso mafanizo a anthu akale omkana ndi
kuonongeka kwawo kuti mafanizo amene wa akhale machenjezo
kwa iwo, ndi kuti asiye makani. Ndipo chinanso ndi
kumulimbikitsa Mtumiki Muhammad (madalitso ndi mtendere
zikhale naye), kupirira ngakhale akumane ndi zovuta zotani
kuchokera kwa anthu opembedza mafano. Ndi kutinso
azithokoza Mulungu pa mtendere umene wampatsa, monga
momwe amachitira anzake, aneneri ndi atumiki.
Komanso Surayi yatchula zimene Mulungu wakonzera anthu
oopa lye, omwe ndimabwerero abwino. Ndi zimene
wawakonzera anthu opyola malire, omwe ndimabwerero oipa.
Kenako yawakumbutsa zimene zidachitika pakati pa tate
wawo Adamu, ndi Iblis, kuti adziwe kuti kudzikweza posiya
kutsatira choona, ndi machitidwe ausatana. Ndi kuti adziwenso
kuti kudzikweza nkomwe kudampirikitsitsa Iblis kuchokera
kuchifundo cha Mulungu.
Ndipo Surayi yathera pofotokoza ntchito ya Mtumiki yomwe
ndikufikitsa uthenga kwa anthu, ndi kuti iye sapempha malipiro
pantchitoyi kuchokera kwa anthu. Ndiponso kuti ntchitoyi
sadampatse anthu koma Chauta ndiye adamtuma. Ndipo Qur'an
ndichikumbutso kwa zolengedwa zonse. Ndipo adzadziwa
kunena zoona kwa aneneri a Mulungu patapita nthawi.
Surat 38. Sad
Juzu 23
972
rr tjA-i
t"A JS ijy*
Surat Sad XXXVIII
s^nw^sfefcor;
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Sad; Ndikulumbira Qur'an
(iyi) ya ulaliki (Wothandiza).
2. Koma amene
sadakhulupirire Akudzitukumula
ndi makani.
3. Kodi ndimibadwo ingati
taiononga Patsogolo pawo?
Adakuwa kuitana (Panthawi
imeneyo), koma nthawi
Yopulumuka idali hatha.
4. Ndipo anadabwa atawadzera
Mchenjezi wochokera mwa
i wo. Ndipo Osakhulupirira adati:
"Uyu ndiwamatsenga; Ngwabodza
lamkunkhuniza!
5. Ha! Waichita milungu
yambirimbiri Ija kuti ikhale
Mulungu mmodzi Yekha? Ndithu,
ichi nchinthu Chodabwitsa."
6. Ndipo adanyamuka
akuluakulu a mwa I wo nati:
Nyamukani Muzikapitiriza
kupembedza Milungu yanu.
Ndithu, chinthu Ichi (nchoipa);
chikulinga ife (Kuti tisiyane ndi
milungu yathu).
7. "Sitidamve zimenezi (zakuti
Mulungu Ndimmodzi ngakhale)
o^l^l^W-
-^
fo$lW&toW&fr
Surat 38. Sad
Juzu 23
973
TT *jk\
TA Jfi 5jj^*
m'chipembedzo Chakale
(chikhrisitu) ichi sikanthu, koma
Ndibodza lopeka."
8. "Kodi uthengawo (wakuti
Mulungu Ndimmodzi)
wavumbulutsidwa kwa iye Pakati
pathu?" Koma iwo Akukaika ndi
ulaliki Wanga. Koma Sadalawebe
chilango Changa.
9. Kodi iwo ali nazo nkhokwe
Za chifundo cha Mbuye wako,
Wamphamvu zoposa, wopatsa
Mochuluka?
10. Kapena ufumu wa
Kumwamba ndi pansi ndi zapakati
Pake, ngwawo. Ngati zili choncho
Atakwera makwerero (kuti akafike
Pamalo poti akalamulire zimene
Akufuna, ngati angathe kutero).
11. Awa (Akuraishi) kuonjezera
pa Kudzitama kwawo, nkagulu
kochepa Ndi kofooka.
Kagonjetsedwa monga Makamu
ankhondo (omwe Adagonjetsedwa
kale omwe amatsutsana Ndi
aneneri akale)..
12. Patsogolo pawo, anthu a
Nuhi, Adi Ndi Farawo, mwini
nyumba zitalizitali (Pyramid),
adatsutsa (aneneri awo)
13. Ndi Asamudu, ndi anthu a
Luti ndi (Anthu a Shuaibu) eni
mitengo Yambiri yothothana,
makamu amenewa.
^ISi^JS 2 *^
Surat 38. Sad
Juzu 23
974 I tr^>»
TA Jfi 5jj-»
14. Onsewa adatsutsa atumiki;
basi Chilango changa
chidatsimikizika (Pa iwo).
15. Ndipo awa (Akuraishi),
sayembekeza China koma mkuwe
umodzi Wosabwereza.(Ndipo
ukadzachitika, Onse adzafa).
16. Ndipo akunena
(mwachipongwe): "O, Mbuye
wathu! Tipatsirenitu gawo La
chilango chathu lisanafike tsiku
Lachi werengero . "
17. Pirira (iwe Mtumiki) ku
zimene Akunenazo (kwa iwe),
ndipo kumbuka Kapolo wathu
Daudi, wamphamvu (pa
Chipembedzo ndi zam'dziko
lapansi). Ndithu lye
ngotembenukira kwa Mulungu
Kwambiri.
18. Ndithu, Ife tidawagonjetsa
mapiri kuti Pamodzi ndi iye
Alemekeze (Mulungu) M'mawa
ndi madzulo.
19. Ndi mbalame zomwe
Zidasonkhanitsidwa Zonse
zimam vera iye.
20. Ndipo tidaulimbikitsa
ufumu wake ndi Kumpatsa uneneri
ndi kuyankhula Kwa luntha
(kosiyanitsira choonaNdi chonama).
21. Kodi yakufika nkhani ya
okangana Pamene adakwera
M%33<j3nc$*#a
^o*u^*ajijBo
©<
&&&&P%1$&
®^WU2
C$£l^}Z.dc%\%0&\
k;\Ms
Surat 38. Sad
Juzu 23
975 tr,>i
VA jp l)$*>
chipupa mpaka Kuchipinda (cha
Daudi Chochitira mapemphero)?
22. Pamene adamulowera
Daudi, adachita Nawo mantha
adati: "Usaope; (Ife) ndife
okangana awiri, mmodzi Wathu
wamchenjerera wina. Weruza
Pakati pathu mwachilungamo,
Usakondere, ndipo tisonyeze njira
Yoongoka."
23. "Ndithu, uyu m'bale wanga
ali ndi Nkhosa makumi asanu ndi
anayi Mphambu zisanu ndi zinayi
(99), ine Ndili ndi imodzi; Ndipo
akuti: "Ndipatse nkhosa Imodziyo
kuti ndizikusungira; ndipo
Wandiposa pakuyankhula.
24. (Daudi) adati: "Zoona,
wakuchitira Zosalungama
pokupempha nkhosa yako Imodzi
kuti aiphatikize ndi nkhosa zake.
Ndithu, ambiri mwa ophatikidzana
nawo Zinthu, ena amachenjerera
ena kupatula Amene akhulupirira
ndi kumachita Zabwino; ndipo iwo
ngochepa." Basi Pamenepo Daudi
adaona kuti Tamuyesa mayeso
(ndipo Sadapambane). Choncho
Adapempha chikhululuko kwa
Mbuye Wake; adagwa ndi
kulambira ndi Kubwerera kwa
Mbuye wake.
25. Choncho tidamkhululukira
iye Zimenezo; ndithu, iye ali nawo
< p&ub'4®&&0&2
Surat 38. Sad
Juzu 23
976
IT tj*r\
VA Jfi 5j^-»
Ulemerero kwa Ife ndi mabwerero
Abwino.
26. "E, iwe Daudi! Ife takuchita
iwe Kukhala woyang'anira
padziko; Choncho weruza pakati
pa anthuwa Mwachilungamo;
ndipo usatsatire Zilakolako kuopa
kuti zingakusokeretse Ku njira ya
Mulungu." Ndithu, Amene
akusokera ku njira ya Mulungu
(Potsatira zilakolako zawo),
chilango Chaukali chili pa iwo
chifukwa cha Kuiwala kwawo
tsiku lachiwerengero.
27. Ndipo sitidalenge thambo
ndi nthaka ndi Zapakati pake
popanda cholinga. Zoterezo ndi
maganizo a amene
Sadakhulupirire. Choncho
Kuonongeka kwakukulu ku moto
Kuli kwa iwo amene
sadakhulupirire.
28. Kodi tingawachite amene
Akhulupirira (Mulungu) ndi
Kuchita zabwino kukhala monga
Oononga padziko? Kapena
tiwachite Oopa (Mulungu) monga
oipa?
29. (Hi), ndibuku lochuluka
madalitso lomwe Talivumbulutsa
kwa iwe kuti (anthu) Azame
kwambiri pomvetsetsa ndime
Zake; ndi kuti apeze nalo phunziro
eni Nzeru.
Siirat 38. Sad
Juzu 23
977
yr tjk-\
VA Jp S^j-*
30. Ndipo Daudi tidampatsa
(dalitso Lobereka) Sulaiman,
amene adali Munthu wabwino.
Ndithu, iye adali Wochulukitsa
kutembenukira kwa Mulungu (ndi
kuzichepetsa M'chikhalidwe chake
chonse).
31. (Kumbuka) pamene
adasonyezedwa Kwa iye m'nthawi
yamadzulo Akavalo ofatsa akaima;
othamanga Kwambiri, akayenda.
32. Ndipo adati: "Ndikukonda
zinthu Zabwino chifukwa
chokumbukira Mbuye wanga,"
Kufikira pomwe (Akavalowo)
adabisika kuseri kwa Chotsekereza
(poikidwa m'makola Mwawo
pomwe iye amafunitsitsa
Kumawaonabe).
33. (Ndipo adati): "Abwezeni
kwaine." Kenako adayamba
kuwasisita M'miyendo ndi
m'makosi (Mwawo).
34. Ndithu, Sulaiman
tidamuyesa (mayeso); Ndipo
tidaika thupi pampando wake;
Kenako adabwerera Kwa
Mulungu.
35. Adati: "O, Mbuye wanga!
Ndikhulukireni Ndipo ndipatseni
ufiimu (umene) Sangaupeze
aliyense pambuyo panga; Ndithu,
inu ndiwopatsa Mochulukitsa."
^W^X^gSW^
iy^\^(3jfiS«SS
Surat 38. Sad
Juzu 23
978
rr tji-i
TA Jp 5j^*»
36. Kenako tidaichita mphepo
yoomba Moleza kuti imgonjere,
yomwe Imayenda mwachifuniro
chake (Sulaimani), paliponse
pomwe Wafuna,
37. Ndiponso (tidamgonjetsera)
asatana; Ena mwa iwo omanga
zomangamanga Ndi obira
m'nyanja zakuya,
38. Ndi ena (mwa asatana)
onjatidwa Mmagoli ndi unyolo,
(Kuti asiye kusokoneza ena).
39. (Ndipo adauzidwa iye): "Izi
(zomwe takudalitsa nazo) ndi
Zopatsa Zathu; choncho mpatse
kapena Mmane (amene wamfuna).
Popanda Kuwerengeredwa.
40. Ndithu, (Sulaiman) ali nawo
Ulemerero waukulu woyandikira
kwa Ife, ndi mabwerero abwino.
41. Kumbuka, (iwe Mtumiki
{SAW}!) kapolo Wathu Ayubu,
pamene adaitana Mbuye Wake:
"Ine wandikhudza satana Ndi
masautso ndi zowawa!"
42. (Tidamuyankha kuitana
kwake, Ndipo tidamuuza):
"Menyetsa miyendo Yako
(panthaka; patuluka madzi) Ozizira
osamba ndi kumwa (Zikuchokera
zomwe uli nazo)."
43. Ndipo tidamubwezera anthu
ake, Ndi kumpatsanso ena onga
a
'\j&&8®&
•d, '
Surat 38. Sad
Juzu 23
979
tr *jk-\
fA Jfi 5jj~»
vmhs\
1^ .v.*
iwo (M'kuchuluka kwawo)
powaphatikiza ndi Omwe adali
nawo; (tidachita zimenezi)
Chifukwa cha chifundo chochokera
Kwa Ife ndi kuti chikhale
chikumbutso Kwa eni nzeru.
44. "Ndipo gwira m'dzanja lako
mtolo Wa zikoti; menya ndi
mtolowo Ndipo usaswe lonjezo."
Ndithu, Ife Tidampeza ali wopirira.
Taonani kukhala Bwino munthu!
Ndithu lye Ngotembenukira
kwambiri kwa Mulungu. 1
45. Kumbukira, (iwe
Mtumiki{SAW}) akapolo Athu
Ibrahima, Isihaka ndi Yakubu, Eni
mphamvu (pa ntchito
yachipembedzo) Ndi kuyang'ana
kozindikira.
46. Ndithu, Ife tidawasankha
powapatsa Chikhalidwe chabwino
(chomwe) ndi Kukumbukira
nyumba yomaliza (Nthawi zonse).
47. Ndithu, kwa Ife iwo adali
mwa anthu Abwino omwe
Adasankhidwa.
48. Ndipo kumbuka Ismail,
Aliyasa, ndi Dzulikifili; ndipo onse
iwo adali mwa Abwino
1 Ayubu adalumbira kuti adzamenya mkazi wake ndi zikoti zingapo. Ndipo
Mulungu adamasula kulumbira kwake kuti atenge mtolo wa zikoti zomwe
m'kati mwake mudali chiwerengero chomwe adalumbirira kuti adzammenya
nacho, ndipo ammenye ndi mtolowo kuti akwaniritse kulumbira kwakeko. Mulungu
adamchitira chifundo chimenechi chifukwa chakuti adapirira pa masautso ake.
%3#W$$fa
Surat 38. Sad
Juzu 23
980
tr *>»
r a Jfi 5jj--
49. Ichi ndichikumbutso (kwa
iwe ndi anthu Ako). Ndipo ndithu,
oopa Mulungu Ali ndi mabwerero
abwino.
50. (Awakonzera iwo) minda
yamuyaya Yotsekulidwa makomo
Ake kwa iwo.
51. (Azidzakhala m'menemo)
uku Atatsamira (mabedi amtengo
wapatali, Ndipo adzakhala
akusangalala) Akuitanitsa
mmenemo zipatso ndi Zakumwa
zambiri;
52. Ndipo (ku Munda wa
Mtenderewo) Adzakhala ndi akazi
oyang'ana amuna Awo okha basi,
ofanana misinkhu.
53. Izi ndi zomwe
mukulonjezedwa pa tsiku
Lachiweruzo.
54. Ndithu, izi ndizopatsa Zathu
Zosatha;
55. Awa ndimalipiro (a oopa
Mulungu)! Koma opyola malire
(Ndi kunyoza aneneri awo), ali ndi
Mabwerero oipa.
56. (Omwe ndi) Jahannama
adzailowa (ndi Kupsereramo).
Taonani kuipa Choyala
chimenecho!
57. Awa ndimadzi wotentha
kwambiri, Ndi mafinya (a anthu a
kumoto). Choncho awalaweko!
®&$^&J&te
Ol^tAp^o^yUtoA
«W$a£g
^y^sfessu
Surat 38. Sad
Juzu 23
981
tr^i
f A Jfi Sjj~-
58. Ndi zilango zina zambiri
Zonga zimenezi.
59. (Kudzanenedwa kwa opyola
malire, Omwe ndiatsogoleri a
opembedza Mafano): "Gulu ili
lalikulu, Lilowa nanu kumoto;
(Omwe adali okutsatirani. Ndipo
Atsogoleri adzati): Siolandiridwa
(Mwamtendere). Ndithu, iwo
ngolowa Kumoto.
60. (Otsatira adzanena):
"Ndithu, Tembereroli likuyenera
inu, (Limene mukutitemberera ife)
Chifukwa inu ndiamene
mudadzetsa Chilangochi
potinyenga ife (ndi Kutiitanira
kunjira yopotoka), Taonani kuipa
(Jahena) malo Okhazikikamo!"
61. (Otsatira) adzanena, "O,
Ambuye wathu! Muonjezereni
chilango kumoto Pamwamba pa
chilango amene Watidzetsera
chilangochi."
62. Ndipo (anthu akumoto)
adzanena "Kodi nchifukwa ninji
sitikuwaona Anthu aja omwe
timawawerengera Kuti ngoipa
(padziko lapansi)?
63. Kodi bwanji timawachitira
chipongwe(Padziko lapansi koma
taonani sadalowe Nafe kumoto).
Kapena kuti Maso athu sakuwaona?"
64. Ndithu, zimenezo,
Zokangana anthu Akumoto nzoona.
w*&y loj&£»5f $&j>\yS
^m% 4 &$%c$%
4Z$^^Mj*£>'&\
*&$$&&&$>&
Surat 38. Sad
Juzu 23
982
yr *>i
TA Jfi 5jj-*»
65. Nena (kwa iwo): "Ndithu
ine ndine M"chenjezi (wochenjeza
za chilango Cha Mulungu). Palibe
wopembedzedwa Mwachoonadi,
koma Mulungu Mmodzi Yekha
Wopambana;
66. Mbuye wathambo ndi
nthaka, ndi Zapakati pake;
Wamphamvu zoposa;
Wokhululuka machimo kwambiri
(Kwa yemwe walapa ndi
Kumkhululupirira)".
67. Nena (kwa iwo iwe
Mtumiki {SAW}): "Ichi (chimene
ndakuchenjezani Nachochi)
ndinkhani yaikulu,
68. Inu, za chimenechi,
mukunyozera!
69. Sindimadziwa chilichonse
za Akuluakulu a pamwamba
(Angelo) pamene amakangana (Za
kulengedwa kwa Adamu)
70. Palibe china chimene
Chavumbulutsidwa kwa ine, koma
(Kuti ndikuuzeni mawu awa oti):
"Ine Ndine mchenjezi (wanu)
woonekera."
71. Akumbutse pamene Mbuye
wako Adanena kwa angelo: "Ine
ndilenga Munthu kuchokera ku
dothi,( Yemwe ndi Adamu).
72. Ndikammaliza ndi
Kumuuzira mzimu wochokera
&jMky35#Gffa$
2$&<.rt
'y&^J&fe^
®M
<tefS8tf
Surat 38. Sad
Juzu 23
983
vr *jA-i
TA Jfi 5jj-*»
Kwa Ine, igwani pansi
Momulemekeza. "
73. Choncho angelo onse
Anagwa pansi momulemekeza."
74. Kupatula Iblis; adadzikuza,
ndipo adali Mmodzi mwa
osakhulupirira.
75. (Mulungu) adati: "E, iwe
Iblisa! Nchiyani chakuletsa kugwa
pansi ndi Kuchilemekeza chimene
ndachilenga ndi Manja anga
(popanda kutuma wina)?
Wadzikweza kapena uli mmodzi
wa Odziika pamwamba?"
76. (Iblis) adanena: "Ine ndine
wabwino Kuposa iye (Adamu);
chiftikwa ine Mudandilenga
kuchokera kumoto, Ndipo iye
mudamulenga Kuchokera kudongo."
77. (Mulungu) adanena (kwa
Iblis): "Tuluka m'menemo
(m'gulu la angelo Apamwamba);
ndithu, iwe Ngopirikitsidwa (ku
chifiindo cha Mulungu).
78. "Ndipo ndithu,
matemberero Anga Akhala pa iwe
kufikira Tsiku lamalipiro.
79. (Iblis) adati: "O, Mbuye
wanga! Ndipatseni nthawi kufikira
tsiku Louka ku imfa."
80. (Mulungu) adati: "Ndithu,
iwe ndiwe Mmodzi wa
wopatsidwa nthawi.
%&#£$$&&% ™
Wasa&ftafrSfc
%^2&U&x&Js
h&j&\&$&'$>
Surat 38. Sad
Juzu 23
984
tr^i
r a jfi ojj-i
81. Kufikira tsiku la nthawi
Yodziwika (imene yaikidwa)."
82. (Iblis) adati: "Choncho
kupyolera Muulemerero Wanu
ndikulumbira kuti Ndiwasokoneza
onse.
83. Kupatula akapolo Anu
omwe ali Osankhidwa mwa iwo.
(Pa iwo Ndilibe nyonga zilizonse)."
84. (Mulungu) adati:
"Ndikulumbira Mwachoonadi
ndipo Ndikunena choona.
85. Ndithudi, ndidzadzazitsa
Jahena ndi Ochokera ku mtundu
wako Ndi omwe adzakutsate mwa
Iwo (ana a Adamu), onse."
86. Nena (iwe Mtumiki{SAW},
kwa Anthuako:)
"Sindikupemphani Malipiro
pazimenezi Ndiponso ine
simmodzi wa Odzikakamiza (pa
zinthu zosandiyenera,)
87. (Qur'an) sichina koma
ndichikumbutso Ndi chiphunzitso
kwa zolengedwa zonse.
88. Ndipo posachedwa
mudziwa, (inu Otsutsa, kuona
kwa) nkhani zake."
t&SF*'™
'\f 6»<i *'^i» '$•" "<t<\
©<r&s^ji
ev&&&£&
4><£*«ftfgSaj
Surat 39. Az-Zumar Juzu 23
985
tfftjA-i r<\jAJ\ij^
Surayi idavumbulutsidwa ku Makka. Koma kukunenedwa
kuti ma aya atatu nga ku Madina. Ndipo ma ayawo ndi awa: 52,
53 ndi 54.
Surayi yayamba ndi kunenetsa za ulemerero wa Qur'an.
Ndipo kenako yaitanira ku zopembedza Mulungu Mmodzi ndi
kuwatsutsa omwe akunena kuti Chauta ali ndi mwana.
Kenako yakamba za kukhoza kwa Mulungu mkalengedwe ka
kumwamba ndi pansi, ndi mkalengedwe ka anthu. Ndi
kunenetsa kuti anthu ngati amkana, lye Ngodzikwaniritsa ndipo
palibe chimene akusaukira kwa iwo. Ndipo ngati amthokoza,
akuyanja kuthokoza kwawo. Koma sayanja kum'kana.
Yakambanso za chikhalidwe cha munthu mmalo awiri,
ponena kuti iye mavuto akamkhudza, amampempha Mbuye
wake ndi kutembenukira kwa Iye modzichepetsa. Koma
akampatsa mtendere amaiwala zomwe adali kupempha kale ndi
zomwe zidampeza.
Ndipo yawakumbutsa chisomo cha Mulungu chomwe chili pa
iwo powatsitsira madzi kuchokera kumwamba omwe akutulutsa
chakudya chawo ndi chakudya cha ziweto zawo. Pazimenezi
pali phunziro ndi chikumbutso kwa eni nzeru.
Kenako surayi ikubwerezanso pofotokoza za Qur'an za
kulowerera m'mitima ya omwe akuopa Chauta, ndikuti Mulungu
wapereka mafanizo osiyanasiyana mmenemo kuti anthu
alingalire za Mulungu. Ndipo kenako yafanizanso pakati pa
munthu wopembedza mafano ndi yemwe akupembedza Mulungu
Mmodzi, ndikunena kuti iwo sali ofanana. Ndipo yanenanso kuti
imfa ndi wo malekezero a onse.
Yafotokozanso za mabwerero a omwe akutsutsa Mulungu ndi
kutsutsa choona. Ndi mabwerero a olungama mzolankhula zawo,
amene akuvomereza zomwe Chauta wavumbulutsa kwa iwo. Ndipo
yatinso kuti mukawafunsa awa opembedza mafano kuti: "Ndani
adalenga thambo ndi nthaka?" Ayankha kuti: "Ndi Mulungu."
Surat 39. Az-Zumar Juzu 23 986 tr *>» r* yjJi 5j>-
Koma iwo kuonjezera pa zimenezo, akupembedza zina
kusiya Mulungu; zimene sizingawateteze ku chilango cha
Mulungu ngati Mulungu atafuna kuwalanga. Ndipo sizingaletse
chifundo cha Chauta pa iwo ngati lye atawachitira chifundo.
Surayi ikunenetsa kuti Bukuli lavumbulutsidwa mwa choona.
Ndipo yemwe aongoke nalo, ubwino wake uli pa iye mwini.
Ndipo amene akhote, uchimo wake uli pa iye mwini. Ndipo
udindo wa Mtumiki ndi kufikitsa uthenga basi, osati kukakamiza
anthu.
Surayi yabwerezanso kukumbutsa zouka ku imfa ndi za
Amushirikina amene adadzipangira milungu yabodza imene
siingawateteze chilichonse.
Pamene yafotokoza mwatsatanetsatane za zoipa za onyoza
opyola malire, zomwe akonzedwera pa tsiku lomaliza, monga
chilango chowawa, yafotokozanso za chifundo chochuluka cha
Mulungu kuti asataye mtima, ponena kuti, "E, inu anthu Anga,
amene mwapyola malire podzichitira nokha zoipa! Musataye
mtima ndi chifundo cha Mulungu. Ndithu, Mulungu
amakhululuka machimo onse; Iye Ngokhululuka kwabasi,
Wachifundo Chambiri." Ndipo yawaitana kuti atembenukire
kwa Iye, chilango chisanawadzere mowadzidzimutsa.
Ndipo tsiku la Kiyama udzaona nkhope zawo, amene
adatsutsa Mulungu, zili zodandaula. Koma amene adaopa
Chauta, zoipa sizidzawakhudza.
Surayi yatsiriza ndi kukamba za tsiku la chitsiriziro.
Kuyamba kwake, nkuimbidwa lipenga lomwe lidzakomola onse
a kumwamba ndi pansi, kupatula amene Mulungu wafuna,
kufikira pom we aliyense adzalandira chomwe ayenerana nacho.
Anthu a kumoto, kunka ku moto; a ku munda wa mtendere,
kunka ku mtendere. Ndipo anthu a ku munda wa mtendere
adzanena ali m'Mundamo: "Kuyamikidwa konse nkwa
Mulungu, Yemwe watitsimikizira lonjezo Lake; waweruza pakati
pa onse mwa choona." Ndipo kudzanenedwanso, "Kuyamikidwa
konse nkwa Mulungu, Mbuye wa zolengedwa."
Surat 39. Az-Zumar Juzu 23 987 tr *>i
r\ >ijji ij^
5«ra/ Az-Zumar XXXIX
mm <
7v ■:
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Kuvumbulutsidwa kwa Buku
ili Kwachokera kwa Mulungu,
Mwini Mphamvu zoposa; Mwini
Nzeru zakuya.
2. Ndithu, Ife takuvumbulutsira
iwe Buku ili mwamtheradi; choncho
Mpembedze Mulungu Momyeretsera
mapemphero lye yekha.
3. Dziwani kuti Mulungu
Ngolandira Mapemphero oyera,
(opanda Kuphatikizidwa ndi zina).
Koma Amene adzipangira
athandizi Kusiya Mulungu,
(akumanena kuti):"Ife
sitikuwapembedza awa, koma
Tikutero ndi cholinga choti
Atifikitse pafupi ndi Mulungu."
Ndithu, Mulungu, adzaweruza
Pakati pawo (pakati pa
okhulupirira Mulungu, ndi okana)
pa zimene Akusiyana. Ndithu,
Mulungu saongola Amene ali
wabodza; wokanira (Mulungu).
4. Mulungu akadafuna kupeza
mwana, Akadasankha yemwe
akum'funa Mzomwe adalenga.
Wapatukana Ndi zimenezo! lye ndi
Mulungu Mmodzi; Wopambana;
Wochita zimene Wafuna.
oi^l^J^U-
-^
®j&m^^&#
a*
Surat 39. Az-Zumar Juzu 23 I 988 I tV ^
x% j^jit o^j—
5. Adalenga thambo ndi nthaka
Mwamtheradi.Amakulunga usiku
Mu usana; ndipo amakulunga
usana Mu usiku. Ndipo dzuwa ndi
mwezi Wazichita kuti zitumikire
monga momwe Afunira. Zonsezi
zikuyenda kufikira Pa nthawi yake
imene yaikidwa. Dziwani kuti lye
(Mulungu) Ngwamphamvu
zoposa; Ngokhululuka Kwambiri.
6. Adakulengani kuchokera mu
mzimu Umodzi (womwe ndi
Adamu; tate wa Anthu). Ndipo
kenako adalenga Kuchokera mu
mzimu umenewo Mnzake, (mkazi
wake, Hawa);
ndipo Adakutsitsirani mitundu
isanu ndi itatu Ya nyama
ziwiriziwiri (zomwe ndi: Ngamira
yaimuna ndi yaikazi, ng'ombe
Yaimuna ndi yaikazi, mbuzi
yaimuna Ndi yaikazi ndi nkhosa
yaimuna ndi Yaikazi. Zonse
pamodzi, zisanu ndi Zitatu, zomwe
mumathandizidwa Nazo kwambiri).
Amakuumbani Mmimba mwa mayi
anu mkaumbidwe Kosiyanasiyana,
mu mdima utatu; (Mu mdima wa
mimba, chiberekero Ndi mdima
wa membuleni). Ameneyo
(Adakuchitirani zonsezi), ndi
Mulungu, Mleri wanu; ufiimu Ngwa
lye. Palibe Wopembedzedwa mwa
choona, koma lye. Kodi nanga
mukutembunuzidwa Bwanji kusiya
Mulungu?
Surat 39. Az-Zumar Juzu 23
989
rr t^r\
T^ yjil 5jj-j
7. Ngati mukana ndithu,
Mulungu Ngodzikwaniritsa
sasaukira kwa inu (Chikhulupiriro
chanu ndi kuthokoza Kwanu);
koma sakonda kukanira kwa Anthu
Ake.Ngati mumthokoza (Pa
mtendere Wake umene uli pa inu)
Akuyanja kuthokoza kwanuko.
Ndipo Mzimu wochimwa
sungasenze machimo A mzimu
wina. Kenako kobwerera Kwanu
nkwa Mbuye wanu, ndipo
Adzakuuzani zimene mudali
kuchita. Ndithu, lye Ngodziwa
zinsinsi Za mmitima.
8. Ndipo masautso akampeza
munthu, Amapempha Mbuye wake
ndi Kutembenukira kwa lye
(pomwe Chikhalirecho adali
kumnyoza). Kenako (Mbuye
wake) akampatsa mtendere
Wochokera kwa lye (waukulu),
Amaiwala (masautso aja) omwe
adali Kumpempha Mulungu kuti
amchotsereAsadampatse
mtenderewo, ndipo Kenako
ndikumpangira Mulungu Milungu
inzake kuti adzisokeretse iye
Mwini (pamodzi ndi ena)
Kuchokera ku njira ya Mulungu.
Nena(Iwe Mtumiki kwa Yemwe
ali ndi Chikhalidwe chotere):
Sangalala ndi Kukanira kwako
(mtendere wa Mulungu) kwa
nthawi yochepa. Ndithu, Iwe ndi
mmodzi wa anthu aku moto.
Surat 39. Az-Zumar Juzu 23
990
tr ftjJt-i
r<* yjii s^
9. Kodi yemwe akudzichepetsa
(kwa Mulungu ndi kumpembedza)
pakati pa Usiku uku akugwetsa
nkhope pansi Ndi kuimirira,
kuopa tsiku la Chimaliziro ndi
kuyembekezera Chifundo cha
Mbuye wake,(kodi Angafanane ndi
yemwe amapempha Mulungu
akakhala pa mavuto pokha,
Akakhala pa mtendere
ndikumuiwala?) Nena (kwa iwo,
iwe Mtumiki {SAW}): "Kodi
amene akudziwa ndi amene
Sakudziwa, ngofanana?" Ndithu,
ndi eni Nzeru amene amalingalira.
10. Nena (kwa iwo mau Anga
akuti): "E, inu Akapolo Anga
amene mwakhulupirira! Muopeni
Mbuye wanu. Ndithu,Amene
achita zabwino zotsatira zake
Nzabwino padziko lapansi ndipo
Dziko la Mulungu ndilophanuka.
(Pirirani chifukwa chosiya midzi
yanu Ndi abale). Ndithu, opirira
adzalipidwa Malipiro awo
mokwana Mopanda mulingo."
11. Nena: "Ine ndalamulidwa
kuti Ndipembedze Mulungu
momuyeretsera Mapemphero Ake
(posam'phatikiza Ndi aliyense pa
mapemphero, kapena Kupemphera
mwa chiphamaso)."
12. "Ndalamulidwanso kuti
ndikhale Woyamba mwaogonjera
(Malamulo Ake)"
^&&\$&M$
u'-TK
®ti^\'$£$&M3
Siirat 39. Az-Zumar Juzu 23
991
tr *>»
rs yjiidjj--
13. Nena: "Ine ndikuopa
Chilango cha tsiku lalikulu,
(Loopsa), ngati ndinyoza Mbuye
wanga."
14. Nena (kwa iwo, iwe
Mneneri{SAW}): "Ndi Mulungu
Yekha ndikumpembedza
Pomuyeretsera lye mapemphero
anga.
15. Choncho pembedzani
zimene mwafuna, Kumsiya lye."
Nena (kwa iwo): "Ndithu, Otaika
ndi kuonongeka kwakukulu,Ndi
amene adzitaya okha, (adziluzitsa
Okha), ndi maanja awo, patsiku la
Kiyama. Dziwa, ndithu, kumeneko
Ndiko kuluza koonekera.
16. Pa iwo padzakhala
misanjikosanjikoYa moto
ndiponso pansi pawo. Ndi chilango
chimenechi, Mulungu
Akuwaopseza nacho akapolo Ake.
"E, inu akapolo AngalNdiopeni!
17. Ndipo amene apatukana
nawo mafano ndi Satana posiya
kuzipembedza, ndikusiya
Kuziyandikira, ndipo mmalo
mwake Nkutembenukira kwa
Mulungu (Pazochita zawo zonse),
nkhaniYabwino njawo
(ponseponse). Auze nkhani
yabwino akapolo Anga.
18. Amene akumvetsera mawu
Ndikutsatira amene ali abwino
'\f 9»s 9 9 " >i;.r >"r^r i ?\2
&$.
*>''%^'&6s&&\
Siirat 39. Az-Zumar Juzu 23
992
rr *>i
r^ yjit djj~»
Kwambiri (ndi oongolera ku
Choona.) I wo wo ndi Amene
Mulungu wawaongola.Ndipo
iwowo ndiwo eni nzeru.
19. Kodi yemwe chiweruzo cha
chilango Chatsimikizika pa iye,
(mungamteteze)? Kodi iwe
ungampulumutse yemwe Ali
mmoto?
20. Koma amene aopa Mbuye
Wawo, iwo adzakhala nazo
Nyumba zikuluzikulu zimene
Zamangidwa mosanjikizana,
Mitsinje ikuyenda pansi Pake. Hi
ndi lonjezo lochokera kwa
Mulungix Mulungu saphwanya
lonjezo.
21. Kodi suona kuti Mulungu
amatsitsa Madzi kuchokera
kumwamba, ndipo Amawalowetsa
mu akasupe mkati Mwanthaka.
Kenako amatulutsa ndi Madziwo
mbewu zosiyana Mitundu:
(chimanga, mpunga, Tirigu, ndi
zina zotere). Ndipo kenako
Imauma (pambuyo pokhala
yobiriwira); Umaiona ili ya
chikasu. Kenako Amaichita
kukhala zidutswazidutswa.
Ndithu, muzimenezo Muli
chikumbutso kwa Eni nzeru
(zofufuzira zinthu).
22. Kodi amene Mulungu
watsekula Chifuwa chake
&&jtta&&l&&v&
Surat 39. Az-Zumar Juzu 23
993
rr *>»
V^ ^»jJl ^jj-*'
povomereza Chisilamu, Kotero
kuti iye akuyenda mkuunika Kwa
Mbuye wake, (angafanane ndi
Yemwe akunyozera kupenyetsetsa
Zisonyezo za Mulungu?)
Kuonongeka Kwakukulu kuli pa
ouma mitima yawo
Posakumbukira Mulungu (ndi
kulabadira Qur'an). Iwo ali
m'kusokera koonekera.
23. Mulungu wavumbulutsa
nkhani yabwino Yomwe ndi Buku
logwirizana nkhani Zake;
(losasemphana).
Lobwerezabwereza (malamulo
ake). Makungu a omwe amaopa
Mbuye Wawo amanjenjemera ndi
ilo. Kenako Makungu awo ndi
mitima yawo Zimakhazikika
pokumbukira Mulungu. Buku
limeneli ndi chiongoko cha
Mulungu; ndi ilo, akumuongola
ameneWamfuna. Ndipo amene
Mulungu Wamulekerera kuti
asokere (chifukwa Chonyozera
kwake choona), sangakhaleNdi
womuongola (ndi ompulumutsa
Ku chionongeko).
24. Kodi yemwe adzakhala
akudzitchinjiriza Ndi nkhope yake
(uku manja atanjatidwa) Ku
chilango choipa pa tsiku la
Kiyama, (Angafanane ndi yemwe
adzakhala Mchisangalalo mminda
ya mtendere?" Ndipo
»~&<. *"<t
'W
Surat 39. Az-Zumar Juzu 23
994
rr *>i
V^ yj\ $jj-»
kudzanenedwa kwa oipa:"Lawani
zoipa za zochita zanu."
25. Amene adalipo patsogolo
pawo, Adatsutsa.Ndipo Chilango
chidawadzera Kuchokera momwe
sadali Kuyembekezeramo.
26. Choncho Mulungu
adawalawitsa Kunyozeka pamoyo
wa padziko Lapansi; koma, ndithu,
chilango cha Tsiku la chimaliziro
nchachikulu zedi (Kuposa chilango
cham'dziko Lapansi) akadakhala
akudziwa!
27. Ndithu, m'buku ili la
Qur'an Taperekamo mafanizo
osiyanasiyana Kwa anthu kuti
akumbukire.
28. Qur'an ya Chiarabu
Yopanda zokhota, kuti Iwo aope
(Mulungu).
29. Mulungu wakupatsani
Fanizo la munthu Wotumikira
mabwana awiri omwe Ngokangana
pa za iye, ndi munthu Yemwe
akutumikira bwana mmodzi. Kodi
awiriwa ngofanana? Kuyamikidwa
konse nkwa Mulungu! Koma
ambiri a iwo sadziwa.
30. Ndithu, iwe udzafa; Naonso
adzafa.
31. (Ndipo) kenako, inu patsiku
La Kiyama m'dzakangana Kwa
Mbuye wanu.
AC^Sp^i^S &(£$\ oOo
Surat 39. Az-Zumar Juzu 24
995 I * i *>■
f^ ^jJl 5jj-*>
32. Kodi ndiyani wachinyengo
Wamkulu woposa yemwe
Akumnamizira Mulungu Zabodza,
ndi kutsutsa choona Chikamdzera?
Kodi Jahannama Simalo a okanira?
33. Ndipo amene wadza ndi
choona, Naachikhulupirira, iwowo
ndiwo Oopa Mulungu.
34. Adzapeza zomwe
adzakhumba kwa Mbuye wawo.
Imeneyo ndiyo mphoto Ya ochita
zabwino.
35. Kuti Mulungu awafafanizire
Zoipa za zochita zawo, Ndi kuti
awalipire malipiro Awo chifukwa
cha zabwino Zomwe adali kuchita.
36. Kodi Mulungu sali
Wokwanira kwa kapolo Wake?
Koma akukuopseza ndi Zina
zomwe similungu! Ndipo yemwe
Mulungu wam'lekerera kuti
asokere, Ndithu, alibe
womuongola.
37. Ndipo amene Mulungu
Wamuongola, palibe amene
Angathe kumsokeretsa. Kodi
Mulungu sali Mwini Mphamvu
Zoposa; Wokhoza kubwezera
chilango?
38. Ndipo ukawafunsa (kuti)
ndani Adalenga thambo ndi •
nthaka, ndithu, Anena (kuti ndi)
"Mulungu". Nena: "Kodi mukuona
Surat 39. Az-Zumar Juzu 24
996
rt cjA-i
r* yjji Sj^
bwanji, amene Mukuwapembedza
kusiya Mulungu Angandichotsere
masautso ake ngati Mulungu
atafuna kundipatsa masautso?
Kapena Mulungu atafuna
kundichitira Chifundo, kodi iwo
angatsekereze Chifundo
Chakecho?" Nena: "Mulungu
akundikwanira! Kwa lye, atsamire
otsamira."
39. Nena: "E, inu anthu anga!
Chitani Zochita zanu mmene
mungathere. Nanenso ndichita
(mmene Ndingathere). Koma
posachedwa mudziwa.
40. Amene chim'dzere chilango
Chomuyalutsa,ndi kum'fikira iye
Chilango chamuyaya."
41. Ndithu, Ife
takuvumbulutsira Buku ili
Chifukwa cha anthu (onse) kuti
Tiwafotokozere choona. Choncho
Amene waongoka, zabwino zake
nza iye Mwini.Koma amene
wakhota, ndiye Kuti
akudzikhotetsa yekha. (Ndipo
Zoipa za kukhotako zidzakhala pa
iye Yekha). Ndipo iwe sikapitawo
wawo.
42. Mulungu ndiye amatenga
mizimu pa Nthawi ya imfa yake
ndipo amatenga Mizimu yomwe
siidafe panthawi Yogona
tulo.Ndipo amaigwira mizimu
Surat 39. Az-Zumar Juzu 24
997
t£ ij*r\
T^ j*£\ *JJ**
Imene wailamula kufa,
(osaibwezera Ku matupi awo).
Koma inayo Amaitumiza
(kumatupi awo, yomwe Nthawi
yake siidakwane) kuti Ikwaniritse
nthawi yake imene Idaikidwa.
Ndithu, m'zimenezi muli
Zisonyezo kwa anthu olingalira.
43. Kodi adzipangira
Apulumutsi kusiya Mulungu?
Nena: "Ngakhale kuti
(Apulumutsiwo) alibe mphamvu
ndi Kuzindikira pa chilichonse?"
44. Nena: "Chiombolo chonse
chili kwa Mulungu; Ufumu wa
kumwamba ndi Pansi Ngwake;
kenako kwa lye M'dzabwezedwa."
45. Ndipo pamene Mulungu
Yekha Akutchulidwa,mitima ya
amene Sakhulupirira tsiku la
chimaliziro Imanyansidwa; koma
akatchulidwa Amene sali lye, iwo
amakondwa.
46. Nena: "E, Ambuye! Mlengi
wa thambo ndi Nthaka! Wodziwa
zobisika ndi Zoonekallnu
mudzaweruza pakati pa Akapolo
Anu pa zimene adali
Kusemphana."
47. Ndipo amene adzichitira
zoipa, ngakhale Kukadakhala kuti
ali nazo zonse Zamnthaka pamodzi
ndi zina zonga izo, Kuti
e&F*
©<z£
Surat 39. Az-Zumar Juzu 24 998 1 t *>i
**j>Phy*
adziombole nazo ku chilango
choipa Cha tsiku la Kiyama,
(sizingavomerezedwe). Ndipo
zidzawaonekera kuchokera kwa
Mulungu, zomwe sadali
kuziyembekezera.
48. Kukawaonekera kuipa Kwa
zimene adazichita, Ndipo
zikawazinga zimene Adali
kuzichitira chipongwe.
49. Pamene munthu mavuto
amkhudza, Amatipempha (uku ali
wodzichepetsa); Koma tikampatsa
mtendere wochokera Kwa Ife,
amanena kuti: "Ndapatsidwa
Mtendere uwu chifukwa
chakudziwa Kwanga (njira
zoupezera)." (Sichoncho) Koma
mtendere umenewu ndi mayeso;
Koma ambiri a iwo sadziwa!
50. Ndithu adanenanso zonga
Zimenezi omwe adalipo Patsogolo
pawo, koma Sizidawathandize
zimene Adali kuchita.
51. Choncho, zidawapeza Zoipa
za zomwe adazichita. Ndipo
amene achita chinyengo Mwa awa,
posachedwa kuwapeza Kuipa kwa
zomwe achita, Ndipo iwo
sangamlempheretse (Mulungu).
52. Kodi iwo sadziwa kuti
Mulungu Akuchulukitsira zopatsa
Zake yemwe Wamfuna, ndi
©£^s$#u*u*
9 . i**' '\99"{\' 9\*' 99\\""
***<*'
Surat 39. Az-Zumar Juzu 24
999
rt »>i
r* ^jJt Sj^-
kumchepetsera (amene Wamfuna)?
Ndithu, m'zimenezi muli
Malingaliro kwa anthu okhulupirira.
53. Nena (kwa iwo mau anga
akuti): "E, inu Akapolo anga!
Amene Mwadzichitira chinyengo,
musataye Mtima ndi chifundo cha
Mulungu. Ndithu, Mulungu
amakhululuka Machimo onse.
Ndithu, lye Ngokhululuka
kwambiri, Wachisoni.
54. Ndipo tembenukirani Kwa
Mbuye wanu, Ndipo m'gonjereni
chilango Chisadakudzereni. Ndipo
zitatero, Sim'dzapulumutsidwa.
55. Ndipo tsatirani zabwino,
zimene Zavumbulutsidwa kwa inu
kuchokera Kwa Mbuye wanu
chisadakufikeni Chilango
mwadzidzidzi pomwe inu
Simkudziwa!"
56. Kuti mzimu usazanene:
"Kalanga ine! Mzomwe
sindidalabadire kumbali ya
Mulungu; ndithu, ndidali mmodzi
wa Ochitira chibwana (zinthu za
Chipembedzo)."
57. Kapena ungazanene:
"Mulungu Akadandiongola,
ndithu, ndikadakhala Mwa oopa
Mulungu."
58. Kapena kunena utaona
chilango: "Ndikadatha kubwerera
&,
*z *>*
Siirat 39. Az-Zumar Juzu 24 iQOO * * *>'
f^ jA^\ OjJ-rf
(Padziko lapansi), ndikadakhala
Mmodzi wa ochita zabwino."
59. (Adzauzidwa: "Nchiyani
iwe?) Ndithu, zidakufika
zisonyezo Zanga, ndipo
udazitsutsa ndi Kudzitukumula;
ndipo Udali mmodzi wa okanira."
60. Ndipo tsiku la Kiyama
Udzawaona omwe adamnamizira
Mulungu, nkhope zawo zili
zakuda. Kodi Jahannama simalo a
Odzitukumula?
61. Ndipo Mulungu
adzawapulumutsa Amene
adamuopa, chifukwa cha
Kupambana kwawo. Zoipa
Sizikawakhudza, ndipo iwo
Sakadandaula.
62. Mulungu ndiye Mlengi wa
chilichonse, Ndipo lye ndi
Myang'aniri wa Chilichonse.
63. Makiyi a kumwamba ndi
Pansi ali kwa lye. Ndipo Amene
akanira zisonyezo za Mulungu,
iwo ndi wo oluza, (otaika).
64. Nena: "Kodi
mukundilamula Kuti ndipembedze
yemwe Sali Mulungu, E, inu mbuli?"
65. Ndipo ndithu,
kwavumbulutsidwa Kwa iwe, ndi
kwa amene adalipo Patsogolo pako
(mawu awa:) "Ngati umphatikiza
(Mulungu ndi milungu yabodza),
Surat 39. Az-Zumar Juzu 24
1001
Yt *>»
r<i yjji o^
Ndithu ntchito zako Zionongeka,
ndipo Ukhala mwa oluza (otaika)."
66. Koma pembedza Mulungu
yekha, ndipo Khala mwa othokoza.
67. Koma sadamlemekeze
Mulungu, Kulemekeza koyenerana
Naye, pomwe Patsiku la Kiyama
nthaka yonse (Idzakhala),
chofumbata Chake mmanja; ndipo
thambo Lidzakulungidwa ndi
Dzanja lake lamanja.
Walemekezeka Mulungu. Ndipo
watukuka Kuzimene
akum'phatikiza nazozi.
68. Ndipo (pamene) lipenga
lidzaimbidwa, Onse a kumwamba
ndi pansi Adzakomoka kupatula
amene Mulungu Wamfuna.Kenako
lidzaimbidwa Lachiwiri;
pamenepo (onse) adzauka;
Adzakhala akuyang'ana
(modabwa: 'Nchiyani chachitika!).
69. Ndipo nthaka (tsiku
limenelo) idzawala Ndi kuunika
kwa Mbuye wake; Ndipo
akaundula a zochita, adzaikidwa.
Ndipo adzabweretsedwa aneneri
ndi Mboni (kuti aikire umboni pa
anthu). Ndipo padzaweruzidwa
pakati pawo Mwachoonadi; ndipo
iwo Sadzaponderezedwa.
70. Ndipo mzimu uliwonse
Udzalipidwa zimene udachita;
y^% oi^i^^^ ^$L
Surat 39. Az-Zumar Juzu 24 1002 * * *j*-'
T^ yj\ 5jj-»
Ndipo lye (Mulungu) Ngodziwa
kwambiri zimene akuchita.
71. Ndipo amene adakanira,
adzakusidwa Ku Jahena ali
magulumagulu kufikira Pomwe
adzaifikira, makomo ake
Adzatsekulidwa, ndipo alonda ake
Adzawauza: "Kodi sadakudzereni
aneneri Ochokera mwa inu
okulakatulirani Zisonyezo za
Mbuye warm, ndi Kukuchenjezani
za kukumana kwanu Ndi tsiku
lanuli?" Adzayankha (nati): "Inde,
adatidzera; koma lidatsimikizika
Liwu la chilango pa okanira."
72. Kudzanenedwa: "Lowani
makomo a ku Jahannama;
mukakhale mmenemo
Muyaya.Taonani kuipa malo a
odzitukumula!
73. Ndipo amene adamuopa
Mbuye wawo, Adzakusidwa kunka
ku Munda wa Mtendere ali
magulumagulu, mpaka Kufikira
pomwe adzaufika. (Adzapeza
Kuti) makomo ake atsekulidwa.
Alonda ake adzanena kwa iwo:
"Mtendere ukhale pa inu
kondwani! Lowani mmenemo,
khalani muyaya."
74. Ndipo iwo adzanena:
"Kuyamikidwa konse nkwa
Mulungu, Amene Watitsimikizira
lonjezo Lake, ndipo Watipatsa
©
Surat 39. Az-Zumar Juzu 24
1003 * £ *>i
r* ^jHojj-
dziko (potipatsa kuti N'lathulathu).
Tikukhala m'minda ya Mtendereyi
paliponse tafuna. Taonani Kukoma
malipiro aochitazabwino!"
75. Ndipo udzaona angelo
atazungulira Mphepete mwa
Mpando Wachifumu Uku
akulemekeza ndi kutamanda
Mbuye wawo. Ndipo
padzaweruzidwa Pakati pawo
mwachoonadi, ndipo
Kudzanenedwa (ndi zolengedwa
zonse): "Kuyamikidwa nkwa
Mulungu, Mbuye wa
zolengedwa!"
©^ij&2#$&££*!3i
Surat 40. Ghafir Juzu 24
1004
Y i »j*-l i . jSlP «j>-
SURAT GHAFIR XL ^^^^B 1
Surayi yayamba ndi zilembo ziwiri za alifabeti, ndipo
yayamba ndi kufotokoza za ulemerero wa Qur'an ponenetsa kuti
idavumbulutsidwa kuchokera kwa Mwini Mphamvu zoposa;
Mwini kudziwa kwambiri; Wokhululuka machimo; Wolandira
kulapa kwa akapolo Ake; Wopereka chilango choopsa kwa
onyoza; Mwini kupereka Mtendere.
Kenako yaitanira ku Umodzi wa Mulungu, ndikuti pasakhale
kunyengedwa ndi ulemerero ndi chuma cha anthu okanira
Chauta. Ndipo yawaitana kuti akumbukire mapeto a anthu akale
ndi zomwe zidawapeza pamene adanyoza aneneri awo.
Yafotokozanso za angero amene akusenza mpando Wachifumu
wa Mulungu ndi kumlemekeza kwawo ndi mapemphero awo.
Ndipo yafotokozanso za mkwiyo wa Mulungu
umene umakhala pa okanira.
Mmalo mwambiri, Surayi yafotokoza zododometsa za Mulungu
ndi kukhoza Kwake koposa komwe kuli mwa iwo eni ndiponso
kumwamba ndi pansi. Ndiponso yafotokoza za mtendere umene
apatsidwa. Ndipo yawalangizanso mma ayah ochuluka kuti
amuyeretsere Chauta chipembedzo Chake. Ndipo mma ayah
ambiri a Surayi muli mawu okumbutsa za tsiku lomaliza.
Yafotokozanso za nkhani ya Musa pamodzi ndi Farawo ndi
anthu ake, makamaka za okhulupirira a kubanja la Farawo.
Ndipo kenako, yalangiza anthu kuti aziyendayenda padziko ndi
kuyang'ana zilango zimene zidawatsikira anthu akale, ndikuti
mapeto a kunyengedwa ndi zamdziko adali otani!
Pamene chilango cha Mulungu chidawatsikira, adati:
"Takhulupirira Mulungu Mmodzi yekha; tikuikana milungu
tidali kuipembedza ija. Koma iwo adakhulupirira nthawi
yoyenera kukhulupirira itatha. Choncho chikhulupiriro chawo
sichidawathandize chilichonse.
Imeneyi ndiyo njira ya Mulungu pa zolengedwa Zake. Panjira
za Mulungu sungapezepo kusintha kulikonse chilango chikatsika.
Choncho panthawiyo adaonongeka okanira Mulungu.
Surat 40. Ghafir
Juzu 24
1005 ***>»
t ♦ J\* Ojj-u
Surat Ghafir XL
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Ha-Mim.
2. Kuvumbulutsidwa kwa Buku
(ili) Kwachokera kwa Mulungu
Wamphamvu Zoposa; Wodziwa
kwambiri.
3. Wokhululukira machimo;
Wolandira Kulapa (kwa yemwe
walapa); Wolanga Mwaukali (kwa
yemwe Wapitiriza kunyoza
Mulungu); Mwini Kupereka
mtendere. Palibe Wopembedzedwa
mwa choona, Koma lye;
kobwerera nkwa lye.
4. Sangatsutsane pa zisonyezo
za Mulungu Kupatula amene
akanira. Choncho Kusakunyenge
kuyendayenda kwawo Padziko
(kunka nachita malonda ndi
Kupeza phindu lalikulu ndi
malondawo Popanda chovuta;
posachedwa Tiwalanga).
5. Iwo kulibe, anthu a Nuhi
adakaniranso Pamodzi ndi
makamu a anthu omwe Adali kuda
aneneri, m'badwo wa Nuh Utatha;
Ndipo m'badwo uliwonse Udaikira
mtima kuchita choipa pa Mneneri
wawo kuti am 'g wire (ndi
Qfa&\vP$\&\j
-a
6^
W^*&V»3f*
Surat 40. Ghafir Juzu 24
1006
rt *>»
t • jdlP *jy**
Kumupha). Adali kutsutsana
Poteteza chachabe kuti ndi uwo
(mtsutso Wawowo) achotse
choona. Ndipo Ndidawaononga
kotheratu. Tayang'ana, Chidali
bwanji chilango changa (pa iwo!)
6. Chonchonso latsimikizika
liwu la chilango Pa okukanira (iwe
Mtumiki{SAW}) Chifukwa iwo
ndi anthu A kumoto (chifukwa
chosankha Kukanira ndi kusiya
kukhulupirira).
7. Amene akusenza Mpando
Wachifumu Ndi amene ali
mmphepete mwake, Akulemekeza
ndi kutamanda Mbuye Wawo,
ndiponso akumkhulupirira lye;
ndipo akupemphera chikhululuko
Amene akhulupirira (ponena kuti):
"E, Mbuye wathu! Chifundo ndi
Kudziwa kwanu kwakwanira pa
Chinthu chilichonse. Khululukirani
Amene alapa ndi kutsatira njira
Yanu; Ndipo apewetseni ku
chilango cha Jahena!
8. E, Mbuye wathu! Alowetseni
ku Minda ya muyaya imene
Mudawalonjeza.Ndi amene
Adachita zabwino mwa atate Awo
ndi akazi awo ndi ana awo. Ndithu,
inu ndi Amphamvu Zoposa;
Anzeru zakuya.
9. Ndipo apewetseni ku zoipa;
tsono Amene mudzampewetsa Ku
%&#&»
> t* * "X ' >" ri^"'
^&&w&t#
Surat 40. Ghafir Juzu 24 1007 * i *>i
i * j31p Sjj-*'
zoipa tsiku limenelo, Ndiye kuti
mwamchitira Chifundo.Ndipo
kumeneko Ndiko kupambana
kwakukulu."
10. Ndithu, amene akanira
adzaitanidwa (Ndi kuuzidwa kuti):
"Mkwiyo wa Mulungu pa inu udali
waukulu kuposa Mkwiyo wanu pa
mitima yanu (yomwe
Yakulowetsani ku chilango)
pamene Mudali kuitanidwa ku
chikhulupiriro, (Ku Chisilamu);
ndipo mudali kukanira.
11. Adzanena: "E, Mbuye
wathu! Mudatipatsa imfa kawiri:
(Imfa Yoyamba, tisanabadwe.
Ndipo imfa ya Chiwiri, padziko).
Ndipo mudatipatsa Moyo kawiri:
(Moyo woyamba wa Padziko
lapansi. Ndipo moyo Wachiwiri
wakuuka kwa akufa). Choncho
tavomereza machimo athu. Kodi
pali njira yotulukira (Ku chilango
kuno)?
12. Zimenezi nchifukwa chakuti
Akapembedzedwa Mulungu
Mmodzi, mudali kutsutsa. Koma
akaphatikizidwa (Ndi milungu
yabodza) mudali
Kukhulupirira.Choncho chiweruzo
ncha Mulungu, Wotukuka,
Wamkulu!
13. lye ndi Yemwe
akukuonetsani Zisonyezo Zake
©ii
*$wzi&&&#z
&>.
Surat 40. Ghafir
Juzu 24
1008
Yt *>l
t * J\£> Sjj^
(zosonyeza Mphamvu Yake
yoposa), ndipo akutsitsa madzi
Kumwamba chifukwa cha inu kuti
Abweretse zokupatsani umoyo;
(Monga chakudya ndi zina). Koma
Palibe amene akukumbukira
kwenikweni Kupatula amene
watembenukira (Kwa Mulungu).
14. Choncho pembedzani
Mulungu Pomuyeretsera
mapemphero Ake Ngakhale
(kumuyeretsera kwanu kwa
Mapempheroko) kuwaipire okanira.
15. lye Ngotukuka ulemerero,
Mwini mpando Wachifumu;
Amapereka chivumbulutso
(Chake) mwa lamulo lake kwa
Yemwe wamfuna mwa akapolo
Ake kuti achenjeze (anthu za) tsiku
Lokumana (anthu onse).
16. Tsiku lomwe iwo
adzaonekera Poyera (kwa
Mulungu). Ndipo palibe
Chilichonse chidzabisidwa kwa
Mulungu (mzinthu zawo). (Ndipo
Adzamva kufunsa koopsa ndi
yankho Loopsa):"Kodi Ufumu
ngwayani lero? Ngwa Mulungu
mmodzi yekha, Wopambana,
(woweruza mmene Akufunira kwa
anthu Ake).
17. Mzimu uliwonse lero,
ulipidwa Zimene udachita; palibe
chinyengo Lero (pochepetsa
©4^
Siirat 40. Ghafir
Juzu 24
1009
Yi *>l
i ♦ yiP dj_^*»
mphoto kapena Kuonjeza
chilango). Ndithu, Mulungu
Ngwachangu (pa) chiwerengero
Chake, (sichichedwa).
18. Achenjeze (iwe,
Mtumiki{SAW}) za tsiku Lomwe
lili pafupi,(Kiyama) pamene
Mitima idzakhala ku mmero
(chifukwa Cha mantha oopsa)
atadzadzidwa ndi Nkhawa.
Wodzichitira chinyengo Sazakhala
ndi bwenzi ngakhale Mpulumutsi
womveredwa (Powateteza iwo).
19. lye (Mulungu ) akudziwa
Kuyang'ana kwa diso la chinyengo
Ndi zimene zifuwa zikubisa
(Mzobisika zonse).
20. Ndipo Mulungu amaweruza
mwa Chilungamo. Koma omwe
Akuwapembedza kusiya Mulungu,
Saweruza chilichonse (chifukwa
cha Kufooka ndi kulephera
kwawo). Ndithu, Mulungu yekha
ndiye Wakumva Woona
(chilichonse).
21. Kodi sadayende padziko
ndikuona Momwe mathero a anthu
akale adalili? Adali opambana
panyonga ndi Mzochitachita zawo
zamdziko kuposa Iwo, (monga
kumanga nyumba Zikuluzikulu).
Koma Mulungu Adawaononga,
psiti! chifukwa cha Machimo awo,
ndipo adalibe Mtetezi ku chilango
cha Mulungu.
J> fit \Sf 9 . < .<* 9 S
Surat 40. Ghafir Juzu 24 ioiO 1 t *>■'
t • jte> djj--
22. Zimenezo nchifukwa
Chakuti ankawadzera aneneri awo
Ndi zizizwa zoonekera poyera,
koma Adazikanira. Choncho
Mulungu Adawaononga
motheratu. lye Ngwanyonga
zambiri, wolanga Mokhwima.
23. Ndipo ndithu, tidamtuma
Musa ndi zizizwa zathu Ndi
zisonyezo zamphamvu Zoonekera
poyera,
24. Kwa Farawo ndi Haamana
ndi Kaaruna. Ndipo adati, "(Uyu)
ndi Wamatsenga, wabodza."
25. Pamene (Musa) adawadzera
ndi Choona chochokera kwa Ife,
(Farawo pamodzi ndi omtsatira)
adati: "Iphani ana achimuna a
okhulupirira Pamodzi ndi iye;
ndipo siyani ana Awo
achikazi."Koma ndale za okanira
Sizakanthu, nzotaika.
26. Ndipo Farawo adati:
"Ndilekeni Ndimuphe Musa;
ampemphe Mbuye Wakeyo (kuti
ampulumutse kwa ine)' Ine
ndikuopera kuti angasinthe
Chipembedzo chanu, Kapena
kufalitsa Chisokonezo padziko."
27. Ndipo Musa adati (kwa
Farawo Pamodzi ndi anthu ake):
"Ine Ndadzitchinjiriza ndi Mbuye
wanga Amenenso ali Mbuye wanu
(ku Chiwembu) chochokera kwa
' Vv? -.f^' t?'•» u, ' f C—^""'
Surat 40. Ghafir Juzu 24
1011 tt*>»
£ • J\* 0jj-»
aliyense Wodzikweza,
wosakhulupirira za tsiku La
chiwerengero.
28. Munthu wokhulupirira,
wochokera Kubanja la Farawo
yemwe adali kubisa Chikhulupiriro
chake, adawalankhula (Anthu ake):
"Kodi muphe Munthu chifukwa
chakuti iye akunena Kuti, 'Mbuye
wanga ndi Mulungu,'
Chikhalirecho wakubweretserani
Zisonyezo zoonekera poyera,
zochokera Kwa Mbuye wanu?
Ndipo ngati ali wabodza
Pazomwe akunena ndiye kuti
Kuipa kwa bodzalo kum'bwerera
yekha. Koma ngati ali woona
(pazomwe Akukulonjezani), ndiye
kuti gawo lina La chilango
chomwe akukulonjezani
Likupezani; ndithu, Mulungu
saongola Munthu wopyola malire,
wabodza la Mkunkhuniza!
29. E, inu anthu anga! Ufumu
walero Ngwanu; mwagonjetsa
dziko (la Iguputo). Ndani amene
Angatipulumutse ku chilango cha
Mulungu ngati chitatidzera?"
Farawo Adati: "Sindikukupatsani
maganizo Koma okhawo ndi
kuwaona (kuti ndi Abwino)
ndiponso sindikukuwongolerani
Koma kunjira yoongoka."
30. Ndipo munthu wokhulupirira
uja Adanena: "E, inu anthu anga!
e£*SM <3?tJ£* <3Kttfj
6©3u»^5^Ji;
Surat 40. Ghafir
Juzu 24
1012
Yi frjJUi
£ * yip Sjj--
Ine Ndikukuoperani (za tsiku la
masautso) Monga tsiku la magulu
omwe (Adaukira aneneri awo).
31. "Monga chikhalidwe cha
Anthu a Nuhi, Adi, Samudi ndi
Anthu omwe adadza Pambuyo
pawo. Koma Mulungu Safuna
kupondereza akapolo Ake.
32. Ndiponso anthu anga! Ine
ndikukuoperani Tsiku la kuitanana
(anthu),
33. Tsiku limene m'dzathawa
ndi Kutembenuza misana yanu;
pomwe Sim'dzakhala ndi mtetezi
ku chilango Cha Mulungu; ndipo
amene Mulungu Wamulekerera
kusokera (chifukwa cha Zochita
zake zoipa), ndiye kuti sangapeze
Muongoli.
34. Ndithu, adakudzerani kale
Yusufu Ndi zisonyezo zoonekera
poyera (Musa asadadze). Koma
simudaleke Kuzikaikira zimene
adadza nazo kwa Inu, kufikira
pamene adamwalira, Mudati:
"Mulungu sadzatumiza Mneneri
wina pambuyo pake." Motero
Mulungu amamulekerera kusokera
Yemwe ali opyola malire,
wokaikira Kwambiri.
35. (Ali ngati awo) amene
akutsutsana za Zisonyezo za
Mulungu popanda Umboni
uliwonse umene wawadzera.
S9' 99. 9<' KX'<*9?\ 9<»\ *
Surat 40. Ghafir Juzu 24 | 1013 | Y £ *>i
£ * yip 5jj--
(Kutsutsa zisonyezo za Mulungu)
Nchokwiitsa Mulungu kwakukulu
ndi Kwa amene akhulupirira (mwa
Mulungu). Momwemo ndi momwe
Mulungu amadindira pamtima wa
Aliyense wodzikuza,
wodzitukumula."
36. Ndipo Farawo adati: "E, iwe
Haamana! Ndimangire Chipilala
kuti ndikafike Kunjira,
37. Njira za kumwamba kuti
Ndikamuone Mulungu wa Musa.
Koma ndithu, ine ndikudziwa Kuti
ameneyu ngonama." Umo ndi
momwe zochita zoipa za Farawo
zidakongoletsedwera kwa iye,
Ndipo adatsekeretsedwa ku njira
yoona Ndipo chiwembu cha
Farawo Sichakanthu, koma
choonongeka.
38. Ndipo uja wokhulupirira
adati: "E, Inu anthu anga!
Nditsatireni; Ndikuongolerani
Kunjira yoongoka.
39. E, inu anthu anga! Ndithu,
Moyo wa padziko lapansi
Ndichisangalalo (chakutha).
Ndithu, tsiku lomaliza Ndiye
nyumba yokhalamo muyaya.
40. Amene akuchita choipa
Sadzalipidwa chinachake Koma
chofanana ndi chomwe Adachita.
Ndipo yemwe Akuchita zabwino,
mwamuna kapena Mkazi, uku iye
A
'^^U^iCr-'t &$3&
$£*• -»• '
Surat 40. Ghafir
Juzu 24
1014
Tt *jir\
i * j31p 3jj~-
ali okhulupirira, iwowo Adzalowa
ku minda ya mtendere.
Adzapatsidwa zopatsidwa
Mmenemo zopanda chiwerengero.
41. E, inu anthu anga! Chifukwa
ninji, ine ndikukuitanirani Ku
chipulumutso ndipo Inu
mukundiitanira kumoto.
42. Mukundiitanira kuti
ndimkane Mulungu, ndimphatikize
ndi milungu Yonama yomwe ine
sindikuidziwa, Pomwe ine
ndikukuitanirani kwa Mwini
mphamvu zoposa; Wokhululuka
kwambiri.
43. Palibe chikaiko, ndithu,
Mukundiitanira kuti
ndiwapembedze Omwe alibe
kuitana kulikonse pano Padziko
lapansi ngakhale tsiku Lomaliza.
Ndipo kobwerera kwathu Nkwa
Mulungu basi. Ndipo, wopyola
Malire (a Mulungu) iwowo ndiwo
anthu Akumoto.
44. Choncho posachedwa,
Mudzakumbukira zimene
Ndikukuuzanizi. Ndipo ine
Ndikutula zinthu zanga Kwa
Mulungu, ndithu, Mulungu akuona
za anthu Ake."
45. Choncho Mulungu
Adam'teteza ku zoipa zomwe
Adam'tchera. Ndipo chilango
e^AWS
Surat 40. Ghafir
Juzu 24
1015
ti *>»
t * j3lP 5jj-»
Choipa chidawazungulira anthu a
Farawo (pamodzi ndi iye mwini.)
46. Zilango za kumoto
zikusonyezedwa Kwa iwo mmawa
ndi madzulo. Ndipo Tsiku lomwe
Kiyama idzapezeka,
(Kudzanenedwa): "Alowetseni
anthu a Farawo ku chilango cha
ukali kwambiri (Choposa chomwe
Adalandira mmanda mwawo)."
47. Ndipo (akumbutse) pamene
Azidzatsutsanam'moto! Pamene
ofooka (Amene amatsatira)
adzanena kwa Omwe adali
kudzikweza: "Ndithu, ife Tidali
otsatira anu; kodi simungathe
Kutichotsera gawo lina la Chilango
cha moto?"
48. Awo amene adadzikweza
adzati: "Ife Tonse tili muno.
Ndithu, Mulungu Waweruza kale
pakati pa anthu Ake. (Choncho
palibe chilichonse chimene
Tingaphulepo)."
49. Ndipo akumoto
adzalankhula kwa (Angelo)
olondera Jahannama:
"Tampempheni Mbuye wanu,
Atipeputsire chilangochi Tsiku
limodzi."
50. (Alonda aja) adzati: "Kodi
Sadakudzereni aneneri anu ndi
Umboni oonekera poyera?" Iwo
Adzati: "Inde, (adatidzera. Koma
£)J*3 J£Mdt£«^J SIS
Surat 40. Ghafir Juzu 24
1016 I y i *>»
i • yiP 5jj~-
ife Tidanyoza)." (Ndipo)
adzawauza: "Choncho pemphani
nokha. Koma Pempho la okanira
silili la kanthu, ndi Lotaika basi."
51. Ndithu, Ife tikupulumutsa
aneneri Athu Ndi amene
akhulupirira pa moyo Wadziko
lapansi ndi tsiku limene
Zidzaimirira mboni (Kupereka
umboni),
52. Tsiku limene achinyengo
Sadzawathandiza madandaulo
awo, Ndipo matemberero
adzakhala pa iwo, Ndipo pokhala
pawo padzakhala Poipa kwambiri.
53. Ndithu, Musa tidampatsa
Chiongoko, ndipo Tidawasiira
Buku ana a Israeli,
54. (Lomwe lidali) chiongoko
ndi Chikumbutso kwa eni nzeru.
55. Choncho pirira, ndithu,
Lonjezo la Mulungu ndi loona.
Ndipo pempha chikhululuko Cha
machimo ako, ndipo lemekeza
Mbuye wako ndikumtamanda
Madzulo ndi m'mawa.
56. Ndithu, amene akutsutsana
pa Zisonyezo za Mulungu popanda
Umboni umene udawadzera,
mmitima Mwawo mulibe
chilichonse koma Kudzitukumula
(ndikufuna ukulu), Koma saufikira.
Dzitchinjirize mwa Mulungu:
ndithu, lye Ngwakumva, Ngopenya.
<M^]&*Mh£^
Surat 40. Ghafir Juzu 24 1017 I Y t ij±\
t * J\* 6jj*>
57. Ndithu, kulenga kwa
Thambo ndi nthaka nkwakukulu
Kuposa kulenga kwa anthu. Koma
anthu ambiri sakudziwa.
58. Wakhungu ndi wopenya
Ndiponso amene akhulupirira Ndi
kumachita zabwino ndi Wochita
zoipa (sali olingana). Zimene inu
mukumbukira Nzochepa, ndithu!
59. Ndithu, Kiyama idza; Ndipo
za iyo palibe chikaiko. Koma
anthu ambiri Sakhulupirira.
60. Ndipo Mbuye wanu
wanena: "Ndipempheni,
ndikuyankhani; Koma amene
akudzikweza ndi Mapemphero
anga (posiya Kundipembedza),
adzalowa ku Jahannama ali
oyaluka."
61. Mulungu ndi Yemwe
adakupangirani Usiku kuti
mupumule mmenemo, ndi Usana
kukhala wounika (kuti muthe
Kuchita ntchito zanu). Ndithu,
Mulungu ndi Mwini Kupereka
ufulu kwa anthu. Koma anthu
ambiri sathokoza.
62. Iyeyo ndiye Mulungu,
Mbuye wanu; Mlengi wa
chilichonse palibe wina
Wopembedzedwa mwa Choona,
koma Iye.Nanga Kodi
mukutembenuzidwa chotani
(Kuchoka ku zoona)!
©WJ&*>))
©<££
• ^•X ,9% J 9S'
Surat 40. Ghafir Juzu 24 | 1Q18 | Y t *>
i • j31p ojj-j
63. Momwemo ndi mmene
Adatembenuziridwa Amene adali
kutsutsa Zisonyezo za Mulungu.
64. Mulungu ndi Amene
adakupangirani Nthaka kukhala
pamalo anu okhalapo, Ndi thambo
kukhala ngati denga (Losagwa);
ndipo adakujambulani
Maonekedwe ndikukongoletsa
Maonekedwe anu; ndipo
adakupatsani Zinthu zabwino.
Ameneyo ndiye Mulungu, Mbuye
wanu. Choncho walemekezeka
Mulungu, Mbuye wa zolengedwa."
65. lye Ngwamoyo Wamuyaya;
palibe Wopembedzedwa wina,
koma lye. Choncho mpembedzeni
momuyeretsera Chipembedzo.
(Musapembedze Milungu ina
mophatikiza ndi lye).
Kuyamikidwa konse nkwa
Mulungu, Mbuye wa zolengedwa.
66. Nena: "Ine ndaletsedwa
kupembedza Amene
mukuwapembedza kusiya
Mulungu, pamene zidandidzera
Zisonyezo zoonekera kuchokera
kwa Mbuye wanga; ndipo
ndalamulidwa Kugonjera Mbuye
Wa zolengedwa zonse."
67. lye ndi Amene
adakulengani kuchokera Ku dothi,
kenako kuchokera kudontho La
umuna, kenako kuchokera
3*
Surat 40. Ghafir
Juzu 24
1019
T£ *&\
t • jSIp Sjj— »
mmagazi; Kenako
ndikukutulutsani muli khanda;
ndipo kenako (adakusiyani) kuti
Mufike nthawi yanyonga zanu.
Ndipo Kenako (adakulekani) kuti
mukhale Nkhalamba. Ndipo ena a
inu Amapatsidwa imfa asadaifike
(Nthawi ya ukalamba) nkuti
muifikire Nthawi imene yaikidwa;
(Zoterezi nkuti inu) mukhale ndi
nzeru.
68. lye ndi Yemwe amapereka
moyo ndi Kupereka imfa; ndipo
akafuna kuchita Chinthu ndithu,
amanenakwa Chinthucho:
"Chitika," ndipo Chimachitika.
69. Kodi sukuona amene
Akutsutsana za zisonyezo za
Mulungu? Kodi nchotani
Akutembenuzidwa (Kusiya
choonadi?)
70- Amene alitsutsa Buku ndi
zomwe Tidawatuma nazo atumiki
athu; Koma posachedwa Adziwa,
71. Pamene magoli ali
m'makosi Mwawo, ndi unyolo Uli
(mmiyendo) akukokedwa,
72. M'madzi otentha, Kenako
m'moto Akuotchedwa,
73. Kenako adzauzidwa: "Hi
kuti (Milungu) imene Mudali
kuiphatikidza (Ndi Mulungu),
®&j*J&i<j\
Sural 40. Ghafir
Juzu 24
1020 I 1 i *&\
t • j3lP 3j^»
74. Mmalo mopembedza
Mulungu?" Adzanena: "Yatisowa:
koma chiyambire Kale sitidali
kupembedza chilichonse (Kupatula
Inu)." Umo ndi momwe Mulungu
akuwalekerera kusokera Okanira.
75. "Izi, (zimene zakupezani ku
Moto kuno), nchifukwa Chakuti
mudali kudzikweza Padziko
mosayenera. Ndiponso Chifukwa
chakuti mudali kunyada.
76. Lowani m'makomo a
Jahannama; mukhala Mmenemo
muyaya. Taonani kuipa Malo a
odzikweza!"
77. Pirira, ndithu, lonjezo la
Mulungu ndiloona. Mwina
Tikusonyeza zina mwa Zomwe
tawalonjeza, kapena Tikupatsa imfa
(usadazione. Basi, Palibe chikaiko,
zichitika chifukwa Chakuti onse)
adzabwezedwa kwa Ife.
78. Ndithu, tidawatuma atumiki
patsogolo Pako; ena mwa iwo
tidakusimbira (Nkhani zawo ndi
maina awo). Ena mwa iwo
sitidakusimbire. Sikudali kotheka
kwa Mtumiki Aliyense kudzetsa
chozizwitsa Mwa yekha, koma
mchifuniro Cha Mulungu. Ndipo
lamulo la Mulungu likadzadza,
Kudzaweruzidwa mwa choonadi.
Ndipo ochita zachabe Panthawi
imeneyo Adzataika; (adzaluza).
H&9S? '\>\ 9 - 9 * } i\}*Y\' 9 \ 9
Surat 40. Ghafir
Juzu 24
1021
Yi *>i
i ♦ yip *jj~*
79. Mulungu ndi Yemwe
Wakupangirani nyama kuti
Mudzizikwera zina mwa izo.Ndipo
zina mwa izo kuti muzidya;
80. Ndipo mmenemo muli
Zokuthandizani zambiri; Ndipo
kupyolera mzimenezo Mukupeza
zofuna za mitima yanu; Pa izo, ndi
pa zombo, Mukunyamulidwa.
81. Ndipo (lye nthawi zonse)
Akukuonetsani zisonyezo Za
chisomo Chake. Kodi ndi Ziti
m'zisonyezo za Mulungu zimene
Mukuzikana (kuti sizake)?
82. Kodi sadayende padziko
ndikuona Momwe adalili mathero
a omwe adali Patsogolo pawo?
Adali ochuluka Kwambiri kuposa
iwo; ndiponso Adali anyonga
kwambiri ndi Ochulukitsa
zomangamanga mdziko. Koma
sizidawathandize zimene adali
Kuchita.
83. Koma pamene atumiki awo
Adawadzera ndi zisonyezo
Zoonekera, adakondwera ndi
Nzeru zomwe adali nazo, (ndipo
Sadalabadire zomwe atumiki
adadza Nazo). Choncho
zidawazinga zimene Adali
kuzichitira chipongwe.
84. Ndipo pamene adachiona
Chilango chathu, adanena (kuti):
"Takhulupirira mwa Mulungu
®&$#<&$&&Af&
9s
t&$$^®®3(m
Surat 40. Ghafir Juzu 24 1022 * $ *j*-i
t • ^dip *jj**'
Mmodzi, ndipo tikuzikana Zimene
tidali kumphatikiza Nazo."
85. Koma chikhulupiriro chawo
sichidali Chowathandiza panthawi
imeneyo, Pomwe adali atachiona
kale chilango Chathu.Ichi ndi
chizolowezi cha Mulungu chomwe
chidapita pa anthu Ake (onse kuti
chilango chikadza, Kulapa
sikuvomerezedwa). Choncho
Pamenepo, okanira adaluza.
Surat 41. Fussilat Juzu 24
1023
1 1 *j£-1 i > cJLad Sjj-»
Surayi yayamba ndi malembo awiri monga njira ya Qur'an
m' Surah zambiri. Ndipo nkhani yaikulu msurayi ndi kufotokoza
za ulemerero wa Qur'an ndi zomwe zili m'kati mwake monga
kupereka uthenga wabwino kwa anthu ochita zabwino, ndi
kuwachenjeza anthu ochita zoipa. Ndiponso yafotokoza za
maganizo a Amushirikina pa Qur'an, monga kuinyoza ndi
kuuthira nkhondo ulaliki wake. Ndi momwe Mtumiki (SAW)
adalimbikirira kuwalalikira iwo powauza kuti: "Ndithu, ine
ndine munthu monga inu. Kusiyana kwanga ndi inu nkwakuti
kwavumbulutsidwa mawu kwa ine oti: "Ndithu, Mulungu wanu
ndi Mulungu Mmodzi yekha. Lungamani kwa lye, ndipo
mpempheni chikhululuko."
Surayi ikukumbutsanso Amushirikina za zisonyezo za Chauta
zolangiza mphamvu Zake zoposa, monga kalengedwe ka
thambo, nthaka, ndi zina zotere. Kenako yaopseza za zomwe
zidawapeza amibadwo yapafupi ndi midzi yawo, monga Adi ndi
Samud. Ndipo ikuwakumbutsanso za tsiku lomaliza; tsiku
limene makutu awo, maso awo ndi khungu lawo zidzawaikire
umboni pa zoipa zimene adali kuchita. Ndipo ikufotokozanso za
mkangano umene udzakhalepo pakati pa iwo ndi ziwalo zawo.
Ndipo yapitirira ndikufotokoza kuti otsatira adzapempha Chauta
kuti atsogoleri awo omwe adali kuwasokeretsa asonyezedwe
kwa iwo kuti athane nawo powaponda ndi mapazi awo.
Monga mwa njira ya Qur'an, ikafotokoza za anthu oipa
imafotokozanso za anthu abwino, chonchonso Surah iyi
yafotokozanso za anthu abwino omwe amanena kuti: "Mbuye
wathu ndi Mulungu." Ndipo kenako ndikupitiriza kuchita
zolungama. Anthu otere alonjezedwa mtendere wamuyaya.
Ndipo yafotokozanso kuti choipa ndi chabwino sizilingana.
Kenako Surayi yadzidzimutsa maso a anthu kuti ayang'ane
zisonyezo za Mphamvu ya Mulungu yomwe ikusonyeza kuti
Chauta adzatha kupatsa moyo akufa. Ndipo yabwerezanso
Surat 41. Fussilat Juzu 24
1024
V t i£r\ t ^ cJUa3 dj^-»
kachiwiri kuopseza anthu opotola zisonyezo za Mulungu
ndikuwauza kuti iwo sangabisike ndi Chauta ngakhale pang'ono.
Ndiponso kuti Buku ili la Qur'an palibe chimene chingapunguke
Mmawu ake, kapena kuonjezeka. Qur'aniyi ndi chivumbulutso
chochokera kwa Wanzeru ndi Wotamandidwa. Ndipo Uthenga
wa Muhammad (SAW) suthenga wachilendo. Koma ukulingana
ndi uthenga umene aneneri a kale adadza nawo.
Ndipo Surayi ikufotokozanso za chikhalidwe cha munthu
ponena kuti akadalitsidwa ndi madalitso ambiri amanyoza choona.
Koma choipa chikamkhudza amapempha Chauta pafupipafupi.
Pomaliza Surayi yanenetsa za mfundo ziwiri zomwe zili
zofunika kwabasi kuposa zolinga zake zonse zimene
yasonkhanitsa. Choyamba ndi kudziwitsa za Qur'an kuti
chimenechi ndi choona; mulibe chokaikitsa chilichonse monga
momwe Mulungu wanenera kuti: "Tiwasonyeza zisonyezo zathu
mbali zosiyanasiyana ndi mmatupi mwawo kufikira zionekere
poyera kwa iwo kuti Qur'an ndi yoona."
Chachiwiri ndikuti palibe chilichonse kwa osakhulupirira
chimene chawachititsa kuti asakhulupirire, koma ndi mtsutso
wawo pa zakuuka kwa akufa.
Siirat 41. Fussilat Juzu 24
1025
tt frj*-i
£ > cJL^ ^jj-*»
Surat Fussilat XLI
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Hd-Mim:
2. (Qur'an iyi)
ndichivumbulutso Chochokera
kwa Wachifundo chambiri,
Wachisoni;
3. (Hi) ndi Buku lomwe ma aya
ake Afotokozedwa (bwino
pokhudza Malamulo a zamdziko
ndi tsiku Lomaliza);
Chowerengedwa (chimene
Chavumbulutsidwa)
m'chilankhulo cha Chiarabu kwa
anthu ozindikira (Tsatanetsatane
wa malamulo ake);
4. Likunena nkhani yabwino
(kwa ochita Zabwino) ndi
kuchenjeza (anthu ochita Zoipa);
koma ambiri a iwo (Akuraish)
Ainyoza kotero kuti sakumva;
(kumva Kothandizidwa nalo ndi
kulilingalira).
5. Ndipo akunena (kuti):
"Mitima yathu (Yaphimbidwa)
m'zivindikiro, ku Zomwe
ukutiitanirazo, ndipo m'makutu
Mwathu muli kulemera kwa
ugonthi; Choncho pakati pathu ndi
pakati pa iwe Pali chotsekereza
o^l^JII^
Surat 41. Fussilat Juzu 24
1026
Tt *>i
t\
dj^
(chotchinga); tero Chita (zakozo);
nafe tichita (zathu; Aliyense wa ife
asalowerere za Mnzake)".
6. Nena: "Ndithu, palibe
chikaiko, ine ndi Munthu monga
inu; Kukuvumbulutsidwa kwa ine
(Kuchokera kwa Mulungu) kuti
ndithu Mulungu wanu ndi
Mulungu Mmodzi; Choncho
lungamani kwa lye ndipo
Mpempheni chikhululuko (pa
zimene Mwakhala
mukumchimwira)" Ndipo
kuonongeka Kwakukulu kuli pa
ophatikiza (Mulungu ndi zinthu
zina),
7. Amene sapereka Chopereka
(zakaat), ndi omwe Akukanira za
tsiku lomaliza.
8. Ndithu, amene akhulupirira
ndi Kumachita zabwino, pa iwo
padzakhala Malipiro osadukiza
(osatha).
9. Nena: "Kodi inu
mukumkanira Yemwe adalenga
nthaka Mmasiku awiri (okha)?
Ndipo mukumpangira Milungu
(ina)? Iyeyo ndiye Mbuye Wa
zolengedwa zonse.
10. Ndipo adaika pamenepo
mapiri Ataliatali pamwamba pake,
ndi Kudalitsapo (ndi madzi,
mmera, ndi Ziweto), ndipo adayesa
mmenemo Zakudya zake (za
^AJVJtJ-J&^U
Surat 41. Fussilat Juzu 24 fl027 * * *>
n
°j>-
okhala pa nthakapo; Zimenezi
adadzichita) mmasiku anayi; (Izi)
nzokwanira kwa ofunsa
(Zakalengedwe ka nthaka ndi
Zamkati mwake).
11. Kenako adaganiza zolenga
thambo Pomwe ilo lidali utsi.
Ndipo adati Kwa ilo ndi nthaka:
"Idzani, mofuna Kapena
mosafuna, (Tsatirani lamulo
langa)." Izo zidayankha Kuti:
"Tadza momvera."
12. Choncho adakwaniritsa
kulenga Thambo zisanu ndi ziwiri
mmasiku Awiri, ndipo thambo
lililonse Adalidziwitsa ntchito
yake (polilamula Zochita zake).
Ndipo tidakongoletsa Thambo
lapafupi (ndi inu) ndi nyenyezi
(Zounikira dziko lapansi),
ndiponso kuti Zizilondera
kumwamba (kuti ziwanda
Zisamapite kukamvera za
kumwamba). Uwu ndi muyeso wa
Mwini Mphamvu, Wodziwa
kwambiri.
13. Koma ngati anyozera
(Kukhulupirira), nena:
"Ndikukuchenjezani za Chilango
monga chilango Cha Adi ndi
Samud."
14. Pamene aneneri adawadzera
patsogolo Pawo ndi pambuyo
pawo (Ndikuwauza):
Surat 41. Fussilat Juzu 24
1028
Ti *>■»
t ^ cJ L^ <>jj~>
"Musapembedze (Milungu ina),
koma Mulungu (Mmodzi)," Adati:
"Mbuye Wathu akadafuna,
akadatsitsa Angelo (Kudzatilalikira,
osati anthu monga Inu). Ndithu, ife
tikuzikana Zimene mwatumidwa
nazozo."
15. Tsono Adi adadzikweza
padziko Mosayenera, ndipo adati:
"Ndani wamphamvu kuposa ife?"
Kodi saona kuti Mulungu Yemwe
adawalenga ndi mwini Mphamvu
zambiri kuposa iwo? Koma
adapitiriza kukanira zozizwitsa
Zathu.
16. Choncho tidawatumizira
mphepo ya Mkuntho yozizira
kwabasi mmasiku Amatsoka, kuti
tiwalawitse chilango
Chowasambula pamoyo wa padziko
Lapansi; ndipo chilango cha tsiku
Lomaliza ndi choyalutsa kwambiri;
Ndipo iwo sadzapulumutsidwa.
17. Naonso Asamudu
tidawasonyeza (njira Yabwino ndi
njira yoipa), ndipo Adakonda ndi
kusankha kusokera Kusiya
chiongoko; ndipo udawapeza
Nkuwe wa chilango choyalutsa
Chifukwa cha machimo Amene
adali kuchita.
18. Koma tidawapulumutsa (Ku
chilango chimenechi) Amene
adakhulupirira ndi Kumamuopa
Mulungu.
%&3
®u%fMp\&$mj
Surat 41. Fussilat Juzu 24
1029
Ti *jfcl
i>
•jj*.
19. Ndipo (akumbutse, iwe
Mtumiki), tsiku Lomwe adani a
Mulungu Adzasonkhanitsidwa
kunka nawo ku Moto, uku
akukusidwa (onse, oyamba Ndi
omalizira),
20. Kufikira pomwe adzaufikira
(moto); Makutu awo ndi maso awo
Ndi khungu lawo zidzawachitira
Umboni pa zomwe adali Kuchita
(padziko lapansi).
21. Ndipo adzanena (adani a
Mulungu) ku Makungu awo:
"Bwanji mukutiperekera Umboni
woipa?" Zidzati: "Mulungu
Watilankhulitsa: Amene
amalankhulitsa Chilichonse; ndipo
lye ndi Amene Adakulengani
(mkulenga) koyamba (Pomwe
simudali kanthu), ndiponso kwa
lye yekha ndiko mudzabwezedwa.
22. Simudathe kubisa (ntchito
zanu zoipa) Ku ziwalo zanu
poopera kuti kumva Kwanu ndi
kuyang'ana kwanu ndi Makungu
anu zingakuperekereni Umboni
woipa! Koma mudali kuganiza
Kuti Mulungu sadziwa zambiri
zomwe Mukuzichita (mobisa).
23. Ndipo amenewo ndi
maganizo anu Omwe mudali
kumganizira (nawo) Mbuye wanu
adakuonongani, ndipo (Lero tsiku
la Kiyama) muli m'gulu la Otaika."
if
Surat 41. Fussilat Juzu 24
1030
Tt fr>i
i>
dj^
24. Choncho ngakhale atapirira
(ku Zopweteka zawo), moto ndiwo
Mabwerero awo ndi kokhazikika
kwawo Kwa muyaya.Ngati
atapempha chiyanjo Cha Mulungu
pa iwo, iwo sadzakhala M'gulu la
oyanjidwa.
25. Ndipo tidawakonzera iwo
abwenzi Oipa (padziko lapansi),
choncho Adawakometsera
zamtsogolo mwawo Ndi za
pambuyo pawo ndipo liwu la
Chilango lidatsimikizika pa iwo
pamodzi Ndi mibadwo yomwe
idapita kale ya Ziwanda ndi anthu,
ndithu iwo adali otaika.
26. Akunena okanira (kuuzana
okhaokha): "Musamvetsere Qur'an
iyi, koma Sokoserani pomwe
ikuwerengedwa (kuti Asaimvere
aliyense) kuti mwina Mupambane."
27. Ndithu tiwalawitsa amene
Akanira chilango choopsa (Pa
zochita zawo zoipa,makamaka
Pakuithira Qur'an nkhondo),
Ndipo ndithu tiwalipira malipiro
oipa Chifukwa cha zoipa zomwe
adali kuzichita.
28. Imeneyo ndi mphoto
yoyenera ya adani a Mulungu,
yomwe ndi moto. Mmenemo
Adzakhala muyaya. Imeneyi ndi
mphoto Ya zimene adali
kuzikanira M'zisonyezo Zathu.
Surat 41. Fussilat Juzu 24 I 1031 1 1 *j*-i
i\
dj^
29. Ndipo okanira adzanena (ali
mkati mwa Mo to): "E, Mbuye
wathu! Tisonyezeni (Magulu awiri)
amene adatisokeretsa. Ochokera
m'ziwanda ndi anthu kuti Tiwaike
pansi pa mapazi athu, kuti Akhale
apansi (mu ulemerero ndi Malo)."
30. Ndithu amene anena (kuti):
"Mbuye Wathu ndi Mulungu,"
(povomereza Umodzi Wake),
kenako nkupitiriza Kulungama pa
malamulo Ake, angelo
Amawatsikira iwo nthawi yakufa
(uku Akuti): "Musaope (pazomwe
Mukumane nazo). Ndipo
Musadandaule (pazomwe
mwazisiya). Ndipo sangalalani ndi
munda Wamtendere umene
mudalonjezedwa (Kupyolera
mmalirime a aneneri).
31. (Angelo amanena kwa iwo):
"Ife ndi Athangati anu pamoyo wa
padziko Lapansi (pokulimbikitsani
panjira Yolungama), ndi tsiku
lomaliza (Pokupempherani
chipulumutso kwa Mulungu); inu
mukapeza kumeneko Chilichonse
chomwe mitima yanu Ikafune
(zokoma ndi zabwino); ndipo,
Mukapeza mmenemo chilichonse
Chomwe mukachilakelake.
32. (Limeneli ndi) phwando
Lochokera kwa (Mbuye)
Wokhululuka Kwambiri,
Wachisoni."
£*'
Surat 41. Fussilat Juzu 24
1032
tt *>»
i>
dj^
33. Kodi ndani yemwe ali ndi
zonena Zabwino kuposa yemwe
akuitanira kwa Mulungu (ndi
kumumvera), Ndikuchita,
(pamodzi ndi zimenezo), Zabwino
uku akunena: "Ine Ndi mmodzi
mwa ogonjera (malamulo a
Mulungu)."
34. Ndipo chabwino
Sichingafanane ndi choipa.
Chotsani choipa (ngati
chitakufikani Kuchokera kwa
mdani), ndi (chinthu) Chabwino;
mapeto ake akhala kuti Yemwe
padali chidani pakati pako ndi
Pakati pake (akhala) ngati
mthandizi Wodalirika.
35. Ndipo palibe angapatsidwe
zimenezi (Zochotsa choipa pochita
chabwino) Kupatula amene apirira.
Ndiponso sangapatsidwe zimenezi
Kupatula mwini gawo la ubwino
waukulu.
36. Ndipo ngati satana
atakusokoneza kuti Akuchotse ku
zomwe walamulidwa, Pempha
chitetezo kwa Mulungu. Ndithu,
lye Ngwakumva zonse, Ngodziwa
zonse; (adzakuteteza Kwa iye).
37. Ndipo zina mwa zisonyezo
Zake, Ndi usiku, usana, dzuwa ndi
mwezi. Musalambire dzuwa
ngakhale mwezi, Koma lambirani
Mulungu (Mmodzi), Amene
Surat 41. Fussilat Juzu 24
1033
t£ *>1
t> c
*lf
adazilenga ngati inu
Mumpembedza moona.
38. Koma ngati adzikweza
(Amushirikina Ndi kusiya kutsatira
lamulo lako, Usade nkhawa).
Ndipo, amene ali Kwa Mbuye
wako; (angelo), akulemekeza lye
usana ndi usiku, ndipo iwo Satopa
(ndi kutamanda Mulungu).
39. Zina mwa zisonyezo Zake
(Zoposa), ndithu, iwe umaona
nthaka Hi youma; koma tikatsitsa
madzi pa iyo Imagwedezeka ndi
kufufuma; ndithu, Amene
waiukitsa nthaka itauma,
Ngoyenera kuukitsa akufa. lye
Ngwamphamvu zoposa Pa
chilichonse.
40. Ndithu, amene akupotoza
choonadi Mzisonyezo Zathu
sangabisike kwa Ife. (Ndipo
tidzawalipira zimene akuyenerana
Nazo). Kodi wabwino ndi uti,
yemwe Adzaponyedwa ku moto,
kapena Yemwe adzadza pa tsiku la
chiweruzo Uku ali wokhazikika
mtima? Chitani Zimene mukufuna;
ndithu, lye Ngopenya chilichonse
chimene Mukuchita. (Aliyense
adzamulipira pa Zochita zake).
41. Ndithu, amene atsutsa
Qur'an Yolemekezeka ikawadzera
(popanda Kulingalira, kwa iwo
kudzakhala Chilango
Siirat 41. Fussilat Juzu 24
1034
tt t,jir\
£\
d J>-"
chosasimbika). Ndipo ndithu,
Limeneli ndi Buku lopambana
(Chilichonse cholipinga).
42. Siifikidwa ndi chonama
patsogolo pake Ngakhale pambuyo
pake. Ndi lovumbulutsidwa
kuchokera kwa Wanzeru zakuya,
Woyamikidwa Kwambiri
(mzochita Zake).
43. Palibe chimene chinenedwa
kwa iwe (Mtumiki{SAW}
kuchokera kwa adani Ako) koma
chomwe chidanenedwa Kwa
aneneri akale (kuchokera kwa
Adani awo). Ndipo Mbuye wako
ndi Mwini chikhululuko chambiri
(kwa Amene walapa kwa lye),
ndiponso Mwini chilango
chowawa (kwa yemwe Wapitiriza
mwano).
44. Tikadaichita Qur'an iyi
kukhala Mchilankhulo china osati
Chiarabu, Akadanena: "Nchifukwa
ninji ma Aya ake sadafotokozedwe
bwino; Buku la chilankhulo
chachilendo Olalikidwa nkukhala
Mwarabu?" Nena (iwe
Mtumiki): "Limeneli ndi
Chiongoko ndi chochiritsa kwa
Okhulupirira. Koma kwa amene
Salikhulupirira (zili ngati kuti)
mmakutu Mwawo muli ugonthi
(chifukwa Cholinyoza).Umene
ukuwachititsa khungu (Chifukwa
choti saona chilichonse Mmenemo
^%&mtit&&Ms
Surat 41. Fussilat Juzu 25
1035
To *>i
i\
°JJ*"
chowapindulitsa) Iwo,okanirawo
ali ngati akuitanidwa Ndi woitana
kuchokera pamtunda Wapatali
(kuti amkhulupirire)."
45. Ndipo ndithu, tidampatsa
Musa Buku (La Taurat.) Ndipo
(anthu ake) adatsutsana Za ilo.
Kukadapanda kutsogola liwu
Lochokera kwa Mbuye wako (loti
Adzachedwetsa chilango kwa
okutsutsa) Kukadaweruzidwa
pakati pawo (Powaononga).
Ndithu, iwo ali M'chikaiko
choikaikira iyo (Qur'an).
46. Amene ati achite chabwino,
Akudzichitira yekha; ndipo amene
Akuipitsa (m'zochita zake),
machimo Ake ali pa iye
yekha. Mbuye wako sali
Wopondereza anthu Ake (polanga
wina Ndi tchimo la wina).
47. Kudziwa kwa tsiku la
Kiyama Kukubwezedwa kwa Iye
(Mulungu;) Zipatso sizituluka
m'mikoko yake ndipo Mkazi
satenga pakati ndi kubereka
Popanda Mulungu kudziwa.
(Koma Amadziwa zonsezo
bwinobwino). Ndipo (kumbukira)
tsiku limene Mulungu
Adzawaitane (ndi kuwafunsa kuti):
"Ali kuti aphatikizi Anga aja
(amene Mudali kuwapembedza
kusiya Ine)?" Adzanena
(modandaula): "Tikukudziwitsani,
Siirat 41. Fussilat Juzu 25
1036
To frjJUi
t>
°J>-
(E, Inu Mulungu)! Palibe aliyense
mwa ife angaikire Umboni (kuti
Inu muli ndi mnzanu)."
48. Ndipo zomwe adali
Kuzipembedza kale zidzawasowa.
Ndipo adzatsimikiza kuti Alibe
pothawira.
49. Munthu satopa kupempha
zabwino (Zam'dziko lapansi kwa
Mbuye wake). Koma choipa
chikamkhudza iye Amakhala
wotaya mtima Kwambiri.
50. Ndipo ndithu, tikamulawitsa
chisomo Chathu atapeza mavuto
kwambiri amene Adamkhudza,
ndithu, amanena, (Monyada): "Izi
nzangazanga. (Ndazipeza
chifukwa Cha khama langa ndi
nzeru zanga): Ndipo za tsiku
lomaliza Sindikhulupirira kuti
lilipo. Ndipo ngati nditabwezedwa
kwa Mbuye wanga, ndiye kuti ine
Ndidzakhala nazo zabwino kwa
Iye." Choncho tidzawauza omwe
adakanira Zimene adachita, ndipo
tidzawalawitsa Chilango
chokhwima (chosanjikana China
pamwamba pa chinzake).
51. Ndipo munthu tikam'dalitsa
ndi chisomo Chathu, amanyoza ndi
Kudziika kutali (ndi chipembedzo
Chathu). Koma vuto likam'khudza
Umuona uyo akuchulukitsa
Maduwa (mapemphero).
Surat 41. Fussilat Juzu 25
1037
To *>t
i S cJUa3 5jj-»»
52. Nena (kwa iwo, iwe
Mtumiki): "Tandiuzani ngati
(Qur'aniyi) ilidi Yochokera kwa
Mulungu, kenako inu Nkuikanira;
(nanga zingakhale bwanji?) Kodi
ndiyani wosokera kwambiri
Kuposa uyo amene ali mumtsutso
Wakutali (ndi choona)?"
53. Posachedwa tiwaonetsa,
(awa okanira), Zisonyezo Zathu
(zosonyeza kuona kwa Qur'an ndi
iwe) kumbali zonse, Ndi mwa iwo
eni kufikira zionekere kwa Iwo
kuti chimene wadza nachochi
Nchoona. Kodi Mbuye Wako
siwokwanira kuti lye Akuona
chilichonse?
54. Chenjerani! Ndithu, awa ali
m'chikaiko Za kukumana ndi
Mbuye wawo. Ndithu, lye (Mbuye
wawo) wachizungulira Chinthu
chilichonse Mkudziwa Kwake.
Surat 42. Ash-Shut a Juzu 25 I 1038 I ** *>' i T c^jj-^' *j>-
SURAT ASH-SHURA XLII ^^S||
— __— _ - — -^ .^^Q^^^f
Surayi yayamba ndi kunenetsa mwandithundithu kuti Qur'an
ndi chivumbulutso chochokera kwa Mulungu potsutsa zimene
ankainenera okanira. Ndipo ikulimbitsa kumtonthoza Mtumiki
(SAW) kumavuto omwe amapezana nawo kuchokera kwa
anthu otsutsa.
Kenako Surayi yalimbikitsa za Mphamvu za Mulungu ndi
ukulu Wake ndiponso ufumu Wake, lye amene adaivumbulutsa.
Koma anthu ena adaikanira ngakhale zisonyezo zake zoti
njochokera kwa Mulungu zili zoonekera. Ndipo yafotokoza
zakusiyana kwawo popeza choonacho.
Surayi yanenanso za kuphatikiza Chauta ndi mafano zomwe
Amushirikina amachita ndi kutsutsana kwawo pa choona
ndikufuna kuti Kiyama idze mwachangu ponena
mwachipongwe.
Surayi yationgolera mmene tingawaitanire anthu ku dini
(mpingo). Ndiponso yafotokoza zakukula kuleza mtima kwa
Mulungu pa anthu Ake.
Kenako surayi yachenjeza zakususuka ndi zamdziko
ndikufotokoza za kuipa kwa chikhalidwe cha anthu okanira pa
tsiku la Kiyama, ndiubwino wa chikhalidwe cha anthu
okhulupirira. Ndipo yafotokozanso zoti Chauta amalandira
kulapa kwa okhulupirira. Ndiponso kuti Mulungu amagawa
riziki (chuma) pakati pa anthu mosiyanitsa: ena olemera, ena
osauka kuti anthuwo asaononge dziko lapansi.
Surayi yapitirira ndi kufotokoza zakukula kwa dalitso la
mvula ndi zisonyezo zolangiza mphamvu za Mulungu padziko.
Ndikuti mavuto am 'dziko lapansi amachitika chifukwa cha
machimo.
Kenako Surayi ikutiuza kuti tichite changu kuyankha kuitana
Surat 42. Ash-Shura Juzu 25 J 1039 I * * *&\ t T ^ jjiJi *j>-
kwa Mulungu, moyo usanathe; imene ndi nthawi yopindulitsa
pogwira ntchito zabwino. Ndipo yanka patsogolo kufotokoza za
mphamvu ya Mulungu pompatsa ana achikazi kapena achimuna
amene wamfuna. Kapena pompatsa ana achikazi pamodzi ndi
achimuna ndi kumchita wina kukhala wosabereka.
Ndipo potsirizira surayi yafotokoza mmene Mulungu
amawalankhulira aneneri Ake. Kenako nkudzamaliza ndi
kulongosola njira yoona yofunika kuitsata.
Surat 42. Ash-Shura Juzu 25 I 1040 I To^i it tfjjiJi *j>->
Surat Ash-Shura XLII
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Hd-Mim,
2. 'Ain-Sin-Qdf.
3. Chomwecho
akukuvumbulutsira iwe Ndi atumiki
amene adadza kale, Mulungu
Ngopambana Wanzeru zakuya.
4. Zonse za kumwamba ndi
pansi ndi za lye Yekha. Ndipo lye
ndi Wotukuka, Wamkulu.
5. (Chifukwa chakukula Kwake
ndi Ulemerero Wake) mitambo
Ikuyandikira kuphwasuka
pamwamba Pa iyo.Ndipo angelo
akulemekeza ndi Kutamanda
Mbuye wawo, ndi kuwapemphera
Chikhululuko amene ali padziko
lapansi. Dziwani kuti ndithu,
Mulungu Yekha ndiye
Wokhululuka kwabasi, Wachisoni.
6. Ndipo awo amene
adzipangira athandizi (A mafano)
kusiya Mulungu, Mulungu Ndi
wofondera (zocfrita) zawo; ndipo
Iwe sikapitawo wawo (wosunga
Zochita zawo).
7. Chomwechonso (monga
chilili Chivumbulutso
chapoyerachi) Takuvumbulutsira
Q^t^i^U,
-£.
($1
Siirat 42. Ash-Shiira Juzu 25 I 1041 I Y o tj±-\ t Y tf jjiJi dj>-
Qur'an m'Chiarabu (Popanda
chikaiko) kuti uchenjeze (Eni)
Likulu la mizinda (Makka) ndi
amene Ali m'mbali mwake,
ndikutinso uchenjeze (Anthu) za
tsiku la msonkhano, lopanda
Chikaiko. (Pa tsikulo anthu
adzagawikana Mmagulu awiri):
gulu Una ku Janna, ndipo Gulu lina
kumoto.
8. Ndipo akadafuna Mulungu
Akadawachita iwo kukhala
Mpingo umodzi; koma akulowetsa
ku Chifundo Chake amene
wamfuna Ndipo odzichitira okha
chinyengo (Pokana Mulungu)
adzakhala opanda Mtetezi kapena
mthandizi.
9. (Kapena adzichitira athandizi
Ena kusiya lye (Mulungu;)
kumachita Kuti Mulungu Yekha
ndiye Mthandizi woona ndipo lye
amaukitsa akufa. Ndipo lye ndi
Wokhoza pa chilichonse.
10. Ndipo chilichonse chimene
mwasiyana Mmenemo
(mchipembedzo: Za Kukhulupirira
ndi kusakhulupirira) Chiweruzo
Chake nkwa Mulungu; (Bwererani
ku Buku la Mulungu ndi Hadith za
mtumiki Wake). Ndipo Ameneyo ndi
Mulungu, Mbuye wanga; Kwa lye
Yekha ndatsamira, Ndipo kwa lye
Yekha (ndiko) Ndikutembenukira.
^m\^i^&
9 <A
t$9 C
'V
Surat 42. Ash-Shura Juzu 25 I 1042 I t a *>i t T <j?jj-iJt «jj~-
11. (lye ndi) Mlengi wa
kumwamba ndi Pansi.
Adakupangirani akazi Kuchokera
mwa inu nomwe, Ndipo nazo
ziweto mitundu Iwiri, (zazimuna
ndi zazikazi. Choncho)
akukuchulukitsani mmenemo
(Mchikonzero Chake chanzeru)
palibe Chilichonse chofanana ndi
lye. lye Ndi Wakumva zonse
ndiponso Woona Zonse.
12. Makiyi a kumwamba ndi
pansi ndi Ake. Amamchulukitsira
riziki amene wamfuna Ndipo
amamchepetsera amene Wamfuna.
Ndithu, lye Ngodziwa
Chilichonse(pochiika pamalo
Oyenerana nacho).
13. Wakhazikitsa kwa inu
chipembedzo Chonga chomwe
adam'langiza Nuhi. Ndipo
chimene takuvumbulutsira iwe
Ndi chimenenso tidavumbulutsira
Ibrahim, Musa, ndi Isa kuti:
Mulimbike Chipembedzo
(potsatira Malamulo) ndikuti
musalekane pa Chipembedzo.
Koma ndizovuta kwa Opembedza
mafano (kuvomera) Zimene
ukuwaitanira. Mulungu
Amadzisankhira amene wam'funa
ndipo Amamuongolera amene
Akutembenukira kwa lye.
14. Ndipo sadagawikane (pa
chipembedzo Otsatira a aneneri
<S2
^&&$&!$&y* \*j
Surat 42. Ash-Shura Juzu 25
1043
tdt>l it iSjj±S\ o jr -
oyamba) kufikira Pamene
kudawadzera kudziwa kwa
Choonadi, chifukwa chachidani
ndi Dumbo pakati pawo.
Kukadapanda Liwu lochokera kwa
Mbuye wako pachiyambi
(Lowachedwetsera chilango)
mpaka Nthawi yoikidwa
kukadaweruzidwa pakati Pawo
koma ndithu, amene adalandira
Buku Pambuyo pawo (makolo
awo, Ndipo ndikukumana ndi
nthawi yako,) Ali mchikaiko
cholikaikira (buku lawo).
15. (Chifukwa cha umodzi wa
zipembedzo Ndikuti pasakhale
kugawikana pa Chipembedzo)
choncho aitanire (Ku chipembedzo
chimodzi); ndipo Lungama
(poitanapo) monga momwe
Walamulidwira. Ndipo usatsatire
zofuna zawo. Ndipo nena:
"Ndakhulupirira mmabuku onse
Omwe adawavumbulutsa
Mulungu; ndipo Ndalamulidwa
kuchita chilungamo Pakati panu.
Mulungu ndiye Mbuye Wathu
ndiponso Mbuye wanu; ife tili Ndi
ntchito zathu (zomwe tidzalipidwa
Nazo); inunso muli ndi ntchito
zanu (Zomwe mudzalipidwa nazo).
Palibe Kukangana pakati pa inu
ndi ife (Chifukwa chakuonekera
poyera Choona).Mulungu
adzatisonkhanitsa (Kuti atiweruze);
kwa lye yekha ndiko Kobwerera.
Surat 42. Ash-Shura Juzu 25
1044
Y p jir\ i Y ^]j-SJt 5j^
16. Ndipo amene akutsutsana
ndi Mulungu pambuyo
povomerezedwa (Ndi anthu
ambiri), Mtsutso wawo
ndiwachabe kwa Mbuye Wawo;
mkwiyo waukulu (wa Mulungu)
Uli pa iwo. Ndipo iwo adzakhala
ndi Chilango chokhwima.
17. Mulungu ndi Amene
Wavumbulutsa Buku (la Qur'an
ndi Mabuku ena) moona ndi
Mwachilungamo. Nanga kodi
nchiyani Chikudziwitse kuti
mwina tsiku la Kiyama lili pafupi?
18. (Limene) akulifulumizitsa
amene Sakulikhulupirira; koma
amene Akhulupirira ali oopa za
tsikulo, ndipo Akudziwa kuti
chimenecho nchoonadi, (Za
kupezeka kwake palibe chikaiko).
Dziwani kuti ndithu, amene
akutsutsana Za nthawi (ya
Kiyama) ali mkusokera Konka
nako kutali.
19. Mulungu Ngoleza kwa
anthu Ake. Amapereka riziki kwa
amene Wamfuna.Ndipo lye ndi
Wamphamvu zoposa; Wopambana.
20. Amene akufuna, pantchito
yake, mphoto Ya tsiku lomaliza,
timuonjezera Mphoto yakeyo;
ndipo amene akufuna, Pantchito
yake yabwino, mphoto ya
Chisangalalo cha m'dziko lapansi,
*H&b&^m'&
hl''\\i.'-H\'l'
Surat 42. Ash-Shiira Juzu 25
1045
To *jJUi
i Y iS^^\ 0jj~-
Timpatsa chimene chidagawidwa
kwa iye, Ndipo iye sadzakhala ndi
gawo (La zabwino) patsiku
lomaliza.
21. Kodi iwo alinayo milungu
imene Idawakhazikitsira
m'zipembedzo Zimene Mulungu
sadaziloleze? Ndipo Pakadapanda
kutsogola (lonjezo lochedwetsa)
Liwu la chiweruzo (Mpaka patsiku
la Kiyama); Pakadaweruzidwa
pakati pa okanira Ndi okhulupirira
(pompano padziko Lapansi).
Ndipo ndithu, achinyengo Chili pa
iwo chilango chowawa. (Cha
Mulungu).
22. Udzawaona (tsiku la
Kiyama) amene Adadzichitira
okha zoipa (Popembedza mafano)
akuopa Chifukwa cha (zoipa)
zomwe adachita, Ndipo
(chilangocho) chidzawapezabe.
Koma amene adakhulupirira ndi
kuchita Zabwino (udzawaona
akusangalala) Mmadimba abwino
a ku Minda ya Mtendere. Iwo
akapeza chilichonse chimene
Akafune kwa Mbuye wawo.
Umenewo Ndiwo ulemelero
wawukulu.
23. Umenewu ndi (ulemerero)
umene Mulungu
Akuwasangalatsira akapolo Ake
nkhani Yabwino; amene
akhulupirira ndi Kuchita zabwino.
Surat 42. Ash-Shura Juzu 25
1046
to frjJt-i 1 1 tf jyJi oj>-
Nena (iwe Mtumiki{SAW} kwa
iwo): "Sindikupemphani malipiro
(kapena chuma) Pofikitsa uthenga
(kwa inu), koma kuti Musunge
chikondi pachibale chimene Chili
pakati pathu. (Musandizunze
Kufikira ndifikitse kwa inu
uthenga wa Mbuye wanga.)"
Amene achita Chabwino
timuonjezera pachabwinocho
Ndithu, Mulungu Ngokhululuka
Kwambiri Ngolandira kuthokoza.
24. Kapena akunena kuti:
"Wampekera Mulungu
Bodza?"Mulungu akadafuna
Akadadinda mumtima mwako
(Kuti usathe kunena chilichonse;
koma Kuti chilichonse chimene
ukunena Chikuchokera kwa lye).
Ndipo Mulungu amachotsa chaboza
(shirik), Ndi kuchilimbikitsa
choona (Chisilamu), ndi mau Ake
(Amene adawavumbulutsa kwa
Mneneri Wake). Ndithu, lye
Ngodziwa zobisika za mmitima.
25. Ndipo lye (yekha) ndi
amene Amavomereza kulapa
kuchokera Kwa akapolo Ake. Ndipo
amakhululuka Machimo (awo);
komanso Akudziwa zimene
mukuchita.
26. Ndipo lye (Mulungu)
akuwayankha Amene akhulupirira
ndi kuchita Zabwino; ndi
kuwaonjezera Ubwino Wake.
$ 9 h i»t<
Surat 42. Ash-Shura Juzu 25
1047
Y o t.jlf\ I Y c£jj-SJ! 5jj~>
Koma okanira Chilango chaukali
chili pa iwo.
27. Mulungu akadachulukitsa
riziki (chuma) Kwa akapolo Ake
onse (monga anthuwo Akufunira),
akadapyola malire (ndi Kuononga)
padziko; koma Mulungu Akutsitsa
(chumacho) mwamuyeso Monga
momwe iye afunira Ndithu, lye pa
za akapolo Ake Ngodziwa.
Ngopenya.
28. Ndipo Iye yekha ndi amene
akutsitsa Mvula atataya mtima (pa
zamvulayo); Ndipo amafalitsa
madalitso Ake Ndipo ndi
Mthandizi Wotamandidwa.
29. Ndipo zina mwa zisonyezo
Zake ndi Kulenga kwa thambo ndi
nthaka, ndi Zamoyo zimene
wazifalitsa mmenemo (Zooneka
ndi zosaoneka). Ndipo Iye ndi
Wamphamvu zowasonkhanitsira
(Anthu kuchokera ku imfa)
akadzafuna.
30. Ndipo mavuto amtundu
Uliwonse amene akukupezani
Nchifukwa cha (zochita zoipa)
Zimene achita manja anu, koma
(Mulungu) akukhululuka zambiri.
31. Ndipo simungathe
kum'lepheretsa (Mulungu
kukutsitsirani mavuto) padziko
Lapansi (ngati mutachimwa);
®$&&\
J*
%£j\£ZZ ^$£AyS&LoiS
<a
*.'? 9' \9%9<"
l^Mj
Surat 42. Ash-Shiira Juzu 25 1048 *° ^j^
1 1 cSjj-^l *JJ~*
ndipo inu Mulibenso mthandizi
kapena mpulumutsi Kupatula
Mulungu.
32. Ndipo zina mwa zisonyezo
Zake ndi Zombo zoyenda panyanja
zonga Mapiri ataliatali (koma
osabira).
33. Atafuna akhoza kuimitsa
mphepo Choncho nkungokhala
duu, (osayenda) Pamwamba pake
(nyanja). Ndithu, mzimenezi muli
Zisonyezo kwa aliyense Wopirira
ndi wothokoza.
34. Kapena akhoza kuziononga
(potumiza mphepo Yamkutho)
chifukwa cha machimo amene
Adawachita. Koma amakhululuka
zambiri.
35. Ndipo adzadziwa (tsiku la
Kiyama) amene Akutsutsana ndi
zisonyezo Zathu kuti alibe
Pothawira (kuchilango cha
Mulungu).
36. Ndipo chilichonse chimene
mwapatsidwa, Nzosangalatsa za
moyo wa padziko. Koma zimene
zili kwa Mulungu ndi Zabwino
ndiponso zamuyaya za amene
Akhulupirira ndi kutsamira Kwa
Mbuye wawo.
37. Ndipo amene akupewa
machimo Akuluakulu omwe
Mulungu waletsa Ndi machimo
¥MB'^\^^
&£^%£$&$#S
©,
\j&&<y}
!**•!,
*$&J&&
Surat 42. Ash-Shura Juzu 25 I 1049 I td^i it tfjysJi ojj-*
onse oipitsitsa;ndipo iwo
Akakwiya (chifukwa choputidwa)
iwo Amakhululuka;
38. Ndipo amene adayankha
kuitana kwa Mbuye wao ndi
kusunga mapemphero
(Popemphera mnthawi yake
Mkapempheredwe koyenera);
ndipo Zinthu zawo zonse
zimakhala zochitira Upo pakati
pa wo; ndipo mzimene Tawapatsa
amapereka (panjira ya Mulungu);
39. Ndi amene Amati
akaputidwa Amadzipulumutsa.
40. Malipiro a choipa ndi
choipa chonga Icho; (wochita
choipa alipidwe Choipa chonga
chimene wachita). Koma amene
wakhululukira wochita Choipa
(pomwe akhoza kubwezera), Ndi
kuyanjana naye (mdani wakeyo),
Malipiro ake ali kwa Mulungu;
Ndithu, Mulungu sakonda ochitira
Anzawo mtopola.
41. Koma amene abwezera
ataputidwa, Kwa iwo palibe njira
Yowadzudzulira.
42. Ndithu, njira
yodzudzulidwira ili kwa Amene
akuputa anthu ndi kudzikweza Ndi
kuononga padziko popanda
Chifukwa choyenera. Iwowo ndi
amene adzalandira Chilango
chowawa.
Surat 42. Ash-Shura Juzu 25 I 1050 I * * * >' i Y ^s)^ «j>-
43. Ndipo amene akupirira ndi
Kukhululuka, (Mulungu
adzamlipira Mphoto yaikulu);
ndithu, kupirirako Ndi chimodzi
mwazinthu zazikulu (Chofunika
kudzilimbikitsa nacho Msilamu pa
chikhalidwe chake.)
44. Ndipo amene Mulungu
wamsiya kuti Asokere, alibe
mthandizi (wina) Kupatula lye
Mulungu. ndipo Udzawaona
osalungama pamene Adzachiona
(masomphenya) chilango,
Adzanena (modandaula): "Kodi
pali Njira yobwerera (padziko
lapansi kuti Tikachite zabwino
tidzalowe ku Janna)?"
45. Udzawaona (osalungama)
Akusonyezedwa ku moto ali
okhumata Chifukwa chakunyozeka
uku akuyang'ana (Moto)
mkayang'anidwe kobisa
(Kotsinzina) .Ndipo amene
Adakhulupirira adzanena pa tsiku
la Kiyama: "Ndithu, otaika ndi
amene Adadzitaya okha pamodzi
ndi maanja A wo." Dziwani kuti
osalungama Adzakhala mchilango
chamuyaya.
46. Ndipo sadzakhala ndi
athangati Owapulumutsa
(kuchilango cha moto) Kupatula
Mulungu. Ndipo amene Mulungu
wamusiya kuti asokere (Chifukwa
?' ^ f :V- 1L\'<'* "" >"{'
%£V
Uc-
*tf*lo#£Sto^
jfrVi
Surat 42. Ash-Shura Juzu 25
1051 *•*>'
t t t£jyZj\ 0j^**i
cha zochita zake zoipa) Sangapeze
njira (yopezera kulungama.)
47. Muyankheni Mbuye Wanu
lisadadze tsiku Losapeweka
lochokera kwa Mulungu; tsiku
limenelo Simudzapeza pothawira,
ndipo Simudzakhala ndi njira
(yokanira Zimene mudzachitidwa).
48. Ngati anyalanyaza
(Mulungu awalanga) Sitidakutume
kwa iwo kukhala
Muyang'aniri.Udindo wako
Ndikufalitsa uthenga. Ndipo
Ndithu, tikamlawitsa munthu
mtendere Wochokera kwa Ife,
akuunyadira (Modzikweza), koma
choipa Chikawapeza kupyolera
mzoipa Zimene manja awo
adatsogoza, pompo Munthuyo
akhala wokanira (Mulungu).
49. Ufumu wakumwamba
ndi padziko Lapansi Ngwa
Mulungu; amalenga Zimene
wafuna; amene wam'funa
Amampatsa ana achikazi ndiponso
Amene wamfuna amampatsa ana
Achimuna.
50. Kapena kuphatikiza (ana)
achimuna Ndi achikazi (kupereka
kwa munthu Mmodzi), ndipo
amene wam'funa Amamchita
kukhala chumba. Ndithu, lye
Ngodziwa; Wokhoza
(chilichonse).
Surat 42. Ash-Shura Juzu 25
1052
ro^i tv is)^ 5j>-
51. Nkosayenera kwa munthu
kuti Mulungu alankhule naye
koma Kupyolera
mkumzindikiritsa, kapena
Kuchokera kuseri kwa
chotsekereza, Kapena pomtuma
mtumiki (Jiburil) Kuti
amvumbulutsire zimene lye
Akufuna mwa chilolezo Chake.
Ndithu, lye Ngwapamwamba;
Ngwanzeru Zakuya.
52. Momwemonso
takuvumbulutsira Chivumbulutso
(Chathu) mwa lamulo Lathu.
Sudali kudziwa kuti Buku ndi
Chiyani, chikhulupiriro ndi
chiyani; Koma Bukuli (Qur'an)
talichita kukhala Kuunika; ndi
kuunikaku tikumuongola Amene
tam'funa mwa akapolo Athu.
Ndithu iwe ukuongolera kunjira
Yoongoka,
53. Njira ya Mulungu Amene
zonse Zakumwamba ndi zamdziko
lapansi Ndi Zake. Dziwani kuti
zinthu zonse Zimabwerera kwa
Mulungu.
Surat 43. Az-Zukhruf Juzu 25
1053
Yo*jjui trJy-ji^j^-
SURAT AZ-ZUKHRUF XLIII
— — -- - - ^^^HG^ L
Surayi yayamba ndi malembo awiri; ndipo yatsatiza
pazimenezi kufotokoza za ulemerero wa Qur'an kwa Mulungu.
Kenako yayamba kufotokoza zamakhalidwe a achibwana
osalabadira uthenga wa Atumiki awo. Ndipo yafotokoza
zisonyezo zambiri zochititsa kukhulupirira mwa Mulungu
Mmodzi. Koma ngakhale zili choncho, okanira, adampangira
Mulungu milungu inzake ndikumpatulira lye ana aakazi, iwo
nkudzipatulira ana aamuna. Ndipo umboni utawasowa pa
zonena zawozi, iwo adangotsatira chikhalidwe cha makolo awo.
Kenako Surayi yafotokoza nkhani ya Ibrahima ndikutsatiza
pankhaniyo kudzitukumula kwa okanira a m'Makka chifukwa
chomvumbulukira Qur'an Muhammad (SAW) osati mmodzi wa
olemekezeka a mmizinda yawo iwiri (Makka ndi Twaif), ngati
kuti iwo ndi amene amagawa zaufulu wa Mulungu. Mulungu
adagawa pakati pawo riziki (chuma) chifukwa cha kusatha
kwawo kugawa. Nanga za uneneri wa Mulungu angamgawire
chotani amene sanamfune?
Kenako Surayi yanenetsa kuti kukadapanda kuopera kuti anthu
angamkanire Chauta onse, akadawapatsa okanira zosangalatsa
zonse pamodzi ndi zokongoletsa zamdziko; okhulupirira
nkudzawapatsa chisangalalo cha muyaya chatsiku lomaliza.
Ndiponso yafotokoza kuti amene salabadira choonadi, Mulungu
amamtumizira Satana yemwe amamtsogolera kuchionongeko.
Kenako Surayi yafotokoza zankhani ya Musa ndi Farawo, ndi
kunyengedwa kwa Farawo chifukwa cha ufumu wake. Ndi
chilango cha Mulungu chimene chidamtsikira Farawoyo. Ndipo
yapitirira ndi kunena nkhani ya mwana wa Mariamu kuti iye ndi
munthu wodalitsidwa ndi Mulungu; adali kuitanira ku njira
yolunjika ndikuopseza za chilango cha tsiku la Kiyama, ndi
kuwauza nkhani yabwino okhulupirira ponena kuti akalowa ku
Munda wa Mtendere, mmene muli zonse zokondweretsa.
Pomaliza Surayi ikunena za ufumu wa Mulungu kuti zonse
nza Iye yekha. Ndikuti milungu imene amamphatikiza nayo
njopanda mphamvu, yachabechabe.
Surat 43. Az-Zukhruf Juzu 25 1054 t o ^jJUi
tV u3yJ-jjl ajj*j
Surat Az-Zukhruf XLII1
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Hd-Mim.
2. Ndikulumbirira Buku
Lofotokoza momveka.
3. Ndithujfe talichita Bukuli
(Qur'an) kukhala Chowerengedwa
m'Chiarabu kuti Muzindikire.
4. Ndipo ndithu, Bukuli
(Qur'an) lachokera M'maziko a
mabuku onse (Lawhi Mahfudh)
amene adachokera kwa Ife; ndipo
ndi Buku lotukuka, La mawu
anzeru
5. Kodi tisiye kukukumbutsani
chifukwa Chakuti ndinu anthu
opyola malire (Pochita zoipa)?
6. Ndipo tidatumiza aneneri
ambiri kwa Anthu akale,
7. Ndipo palibe mneneri
aliyense amene Amawadzera koma
amam'chitira Chipongwe.
8. Choncho tidawaononga
amene Adali amphamvu kuposa
iwo (Akuraish) Ndipo afika
mafanizo a zilango Zomwe
zidawapeza anthu akale.
9. Ndipo ukawafunsa: "Ndani
adalenga thambo ndi Nthaka?"
Q^lfc^l^lj
^MS^^i^^sf
^#$&EUW3&Sft
(^%o^(?^Irj<V3Uc^i
Siirat 43. Az-Zukhruf Juzu 25
1055 to^i
i T ^j*^ 5j>-»
Ndithu, ayankha Kuti: "Adazilenga
(Mulungu) Mwini Mphamvu,
Wodziwa."
10. Amene wakupangirani
Nthaka kukhala monga Choyala
ndipo adakupangirani Njira
mmenemo kuti muongoke
(Ndikukafika kumene mukufuna);
11. Ndiponso Amene watsitsa
madzi Kuchokera kumwamba
Mwamuyeso; chifukwa cha
Madziwo tidaukitsa mudzi
Wakufa. Momwemonso inu
Mudzatulutsidwa (mmanda);
12. Ndiponso Amene walenga
zinthu zonse Ziwiriziwiri,
(chachimuna ndi Chachikazi).
Ndipo adakupangirani Zombo ndi
ziweto zimene mukukwera,
13. Kuti mukhazikike
mwaubwino Pamisana paizo,
kenako mukumbukire Mtendere
wa Mbuye wanu Mukakhazikika
pamenepo, ndipo Munene:
"Walemekezeka Amene
Watifewetsera ichi; ndipo
sitikadatha Kuchifewetsa ndi
kuchigwiritsa ntchito.
14. Ndipo ndithu, ife kwa
Mbuye wathu ndiko tidzabwerera."
15. Ndipo amuikira gawo Mwa
akapolo Ake. (Kuti ndi ana a
Mulungu.) Ndithu munthu,
Ngwamsulizo woonekera poyera!
?*\'\iK* ' 9 i\ * 9£f*
W^e
Surat 43. Az-Zukhruf Juzu 25
1056
to^t tr «J^jJiSj>-
16. Kodi wadzichitira ana
achikazi Mzimene wazilenga
ndipo Wakusankhirani inu ana
achimuna?
17. Koma akauzidwa (kuti
wabereka mwana Wachikazi)
mmodzi wa iwo chomwe
Amamfanizira (Mulungu)
Wachifundo Chambiri, nkhope
Yake imakhala yakuda Ndi
kudandaula kwambiri!
18. Ha! Kodi amene watered wa
monga Chokongoletsa, potsutsana
iye sangathe Kunena momveka?
(Ameneyo ndiye Mwampatsa
Mulungu; omwe ndi ana Achikazi).
19. Ndipo angelo omwe ndi
akapolo a (Mulungu) Wachifundo
chambiri Akuwatcha akazi.Kodi
adaona kalengedwe Kawo?
Umboni wawo ulembedwa Ndipo
adzafunsidwa (pazimenezo)!
20. Ndipo (okanira) akunena:
"Akadafuna (Mulungu)
Wachifundo chambiri (kuti
Tisamapembedze mafano awa),
Sitikadawapembedza!" Iwo alibe
kudziwa pazimenezi (zomwe
Akunenazi). Koma akungonena
mawu Opeka.
21. Kapena tidawapatsa Buku
lina tisadapereke Hi, kotero kuti
iwo akugwiritsa Limenelo (ndi
kugwirizana nazo Zili mmenemo)?
$&*&&&&$
© (
J^d&*S$<Xti&&
®&#.
f *&
*'
Surat 43. Az-Zukhruf Juzu 25
1057 *•*>» ir^jr}\*^
22. Koma akunena: "Ndithu, ife
Tidawapeza atate athu pa
Chipembedzo Chimenechi, ndipo
ife Tikutsatira mapazi awo,"
23. Ndipo momwemo,
sitidatumize mchenjezi Patsogolo
kumudzi uliwonse koma Olemera
ammenemo adanena: "Ndithu,
tidawapeza atate athu Pa
chipembedzochi (akuchita
mmene Tikuchitiramu), ndipo ife
titsatira Mmapazi awo."
24. Adanena (mneneri wawo):
"Ngakhale Ndakubweretserani
chipembedzo Chabwino kuposa
chomwe Mudawapeza nacho atate
anu (Mupitirizabe kutsatira
chipembedzo Cha makolo
anucho)?" Adanena: "Ife tikuzikana
zimene Mwatumidwa nazozi."
25. Choncho tidawalanga iwo.
Taona m'mene adalili Mapeto a
otsutsa aja.
26. Ndipo (kumbuka) pamene
Ibrahim Adauza bambo wake ndi
anthu ake (kuti): "Ndithu, ine
ndadzipatula kuzimene
Mkuzipembedzazi,
27. Kupatula Amene
Adandilenga; ndithu, lye
andiongola."
28. Ndipo adalichita liwu ili
kukhala Losatha ku mtundu wake,
© <&££M$ 32*<$$fcSl
J&itf&gfc&fc}
Surat 43. Az-Zukhruf Juzu 25
1058
to *jjfe.|
tv ciyj-jii 3jj-*>
Kuti abwerere (Ku malankhulidwe
amenewa).
29. Koma ndidawasangalatsa
awa (Akuraish) pamodzi ndi atate
awo Kufikira choonadi
chawadzera ndi Mtumiki
wolongosola (za choonadichi).
30. Ndipo pamene choonadi
(Qur'an) chidawadzera, adanena:
"Awa ndi matsenga; ndithu, ife
Tikuakana."
31. Ndipo adatinso:
"Nchifukwa ninji Qur'an iyi
siidavumbulutsidwe Pamunthu
wamkulu Mmidzi iwiriyi (Makka
ndi Taif,)"
32. (Choncho Mulungu
akunena): "Kodi Iwo ndi amene
akugawa mtendere wa Mbuye
wako (kumpatsa amene Wamfuna
ndi kumana amene sakufuna
Kumpatsa? Chikhalirecho) Ife ndi
Amene timagawa pakati pawo
zofunika Pamoyo wawo mu moyo
wadziko Lapansi; ndipo
tawatukula ena mwa iwo Pa
ulemerero pamwamba pa ena,
Choncho ena mwa iwo akuwachita
Anzawo kukhala antchito awo
Koma mtendere wa Mbuye wako
ndi wabwino kuposa Zimene
akusonkhanitsa.
33. Ndipo pakadapanda kuopera
kuti anthu Adzakhala gulu limodzi
fc^j.ts«&j|<asir;
Surat 43. Az-Zukhruf Juzu 25
1059 I t © ,>i it Jj^ jli 5^
(lokanira Mulungu), ndithu,
tikadazichita Nyumba za amene
akumkana (Mulungu) Wachifundo
Chambiri kukhala ndi Madenga a
Siliva, ndi makwerero Amene
amakwerera (Kukhalanso a Siliva),
34. Ndipo nyumba zawo
kukhala ndi zitseko Ndi makama
(mabedi) amene Amayadzamira
(zonse Kukhala za Siliva),
35. Ndiponso ndi zokongoletsa
za golide. Koma zonsezo sikanthu
ayi, ndi Chisangalalo chabe chadziko
lapansi (Chosakhalira kutha);
ndipo tsiku Lomaliza lomwe lili
kwa Mbuye wako Ndi la oopa
Mulungu (potsatira Malamulo Ake
ndi kusiya zoletsedwa).
36. Ndipo amene akunyozera
kukumbukira (Mulungu)
Wachifundo Chambiri, Timpatsa
Satana, kuti iye akhale Bwenzi
lake (lotsagana nalo).
37. Ndipo iwo amawatsekereza
kunjira Zabwino ndi kumaganiza
Kuti iwo ngoongoka.
38. Kufikira pamene
adzatidzera (Tsiku la Kiyama, uku
akulowetsedwa Ku moto). Adzati
(kumuuza Satana): "Kalanga ine!
Pakati pa iwe ndi ine Pakadakhala
mtunda wa pakati pa Kuvuma ndi
kuzambwe (kutalikirana Kwathu)."
Ha! Taonani kuipa kwa bwenzi!
^m&&%$v&
i< **t\ \9 4i. 9S 9' \j>* 9"
Surat 43. Az-Zukhruf Juzu 25
1060
to frjA-i tr cJy-jJidjj--
39. (Mulungu adzawauza kuti):
"Ndipo lero Sikukuthandizani
kukhala limodzi kwanu M'chilango
pakuti mudadzichitira nokha Zoipa.
40. Kodi ungathe kuwamveretsa
Agonthi, kapena ungathe
Kuwaongola akhungu ndi amene
Ali mkusokera koonekera?
41. Ngati titakuchotsa (padziko
usadaone Chilango chawo,
usakhale ndi chikaiko), Ndithu, Ife
tiwalanga iwo,
42. Kapena tikusonyeza zimene
Tidawalonjeza (uona ndi maso ako
Usadafe). Ndithu, Ife till ndi
mphamvu Pa iwo.
43. Choncho, gwiritsa zimene
Zavumbulutsidwa kwa iwe, ndithu,
iwe Uli panjira yolunjika.
44. Ndithu, iyi (Qur'an) ndi
ulemerero Wako ndi anthu ako;
ndipo posachedwa Mufunsidwa
(za ulemerero umenewu).
45. Ndipo afunse aneneri Athu
amene Tidawatumiza iwe usadadze:
"Kodi Tidapanga milungu ina kuti
Ipembedzedwe, osati Mulungu
Wachifundo Chambiri?"
46. Ndithu, tidamtumiza Musa
pamodzi Ndi zozizwitsa Zathu
kwa Farawo Ndi nduna zake; ndipo
adati: "Ndithu, ine ndine Mtumiki
wa Mbuye wa zolengedwa."
&&&$$ify®®sii
$*%&&&&%&
®"'>&
Surat 43. Az-Zukhruf Juzu 25 1061 I * o ^i i r *Jj*^ 5j>-
47. Koma pamene adawadzera
Ndi zisonyezo zathu, basi Iwo
adali kuziseka.
48. Ndipo chisonyezo
chilichonse chomwe
Tidawasonyeza chidali chachikulu
Kuposa chinzake (komabe
Sadakhulupirire). Ndipo
tidawalanga Ndi chilango kuti
abwerere (kwa Ife).
49. Ndipo adati (kwa Musa):
"E, iwe Wamatsenga! Tipemphere
Kwa Mbuye wako pachomwe
Adakulonjeza; ndithu, ife
Tiongoka, (tikhulupirira)."
50. Choncho, pamene
tidawachotsera Chilangocho, basi
iwo adayamba Kuswa pangano.
51. Ndipo Farawo adaitana
anthu ake, Adati: "E, inu anthu
anga! Kodi Ulamuliro wa mu
Iguputo Siwanga pamodzi ndi
mitsinje iyi Imene ikuyenda pansi
panga (pa nyumba Zanga?) Kodi
simukuona?
52. Kodi kapena ine sindine
woposa uyu (Musa) wonyozeka,
Ndipo sangathe Kulankhula
momveka?
53. Nanga bwanji sadapatsidwe
Zibangiri zagolide kapena Angelo
kudza pamodzi Ndi iye uku
akumtsatira?"
t&£ %j$\^&j&*1
Surat 43. Az-Zukhruf Juzu 25
1062 I to,>i
it Jy-jJl «jj~»
54. Adawapeputsa anthu ake.
Ndipo Adamvera; iwo adali anthu
otuluka Mchilamulo (cha Mulungu).
55. Pamene adatikwiitsa,
tidawalanga Ndipo tidawamiza
mmadzi onse.
56. Tidawachita (Farawo ndi
anthu ake) Kukhala chitsanzo cha
okanira A pambuyo pawo
ndikukhala mbiri Kwa anthu
amene akudza.
57. Ndipo pamene
lidaperekedwa fanizo la Mwana
wa Mariam, pamenepo anthu anu
Adali kufuula (monyoza). 1
58. Ndipo adati: "Kodi milungu
yathu Ndi yabwino, kapena iye?"
Sadamfanizire kwa iwe koma
kufuna Kutsutsana basi (kopanda
kufuna Choona). Koma iwo ndi
anthu amtsutso.
59. Iye sadali kanthu koma ndi
kapolo Amene tidampatsa
Mtendere; Ndipo tidamchita
kukhala chitsanzo (Chodabwitsa)
cha ana a Israeli.
% 9 2$!&&3?&*jfc&
&%&&$%&$$&
%^^'S^i
Fanizo lomwe likunenedwa apa ndi lomufanizira Yesu ndi zomwe
zikupembedzedwa kusiya Mulungu. Akafiri adamfanizira iye pambuyo
povumbulutsidwa aya yakuti: "Ndithu inu ndi zomwe mukuzipembedza kusiya
Mulungu ndi nkhuni za ku Jahannama." Choncho adati Yesu nayenso akalowa
ku moto chifukwa chakuti Akhrisitu amamupembedza kusiya Mulungu. Koma
Mulungu adamyeretsa ponena kuti: "Ndithu awo amene ubwino wochokera
kwa Ife watsogola kwa iwo, iwowo akatalikitsidwa ndi iwo (motowo)" Choncho
Yesu sakalowa kumoto chifukwa iye sadalamule anthu kuti amupembedze
komanso sakudziwa kuti pali aliyense amene akupembedza iye.
Surat 43. Az-Zukhruf Juzu 25
1063 f**j*-»
tT <J)jS>-^\ 5jj»*»
60. Ndipo tikadafuna
tikadawachita angelo Kukhala
padziko mmalo mwa inu ndi
Kumasiirana iwo kwa iwo (kuti
mudziwe Kuti angelo akugonjera
malamulo a Mulungu, iwo
simulungu).
61. Ndipo iye (Isa) adzakhala
chizindikiro Cha Kiyama (kuti
yayandikira). Choncho
Musaikaikire, koma nditsatireni.
Imeneyi ndi njira yolunjika.
62. Asakutsekerezeni satana;
iye Kwa inu ndi Mdani woonekera.
63. Ndipo pamene Isa adadza
ndi zisonyezo Zoonekera poyera,
adati: "Ndakudzerani Ndi nzeru
(yopindulitsa), ndikuti
Ndikulongosolereni zina zimene
Mudali kusiyana mu izo; choncho,
Muopeni Mulungu ndiponso
ndimvereni.
64. Ndithu, Mulungu ndiye
Mbuye wanga Ndi Mbuye
wanunso; choncho
Mupembedzeni; imeneyi ndiyo
njira Yolunjika."
65. Koma adapatukana pakati
pawo Mmagulumagulu.
Kuonongeka ndi Chilango chatsiku
lowawa kudzakhala Kwa amene
adzichitira okha zoipa.
66. Palibe chimene
akuyembekeza, koma Kiyama basi
^ <9* 9A9*
®.
m&^^'*&
x&3%&\%&3&;&
Surat 43. Az-Zukhruf Juzu 25
1064
yotj)r\ tr J/jliSj^-
yomwe iwadzera Mwadzidzidzi
pomwe iwo sakuzindikira (Ali
otanganidwa ndi zam'dziko).
67. Abwenzi tsiku limenelo
adzakhala Odana, wina ndi
mnzake, (chifukwa Chakuti adali
kuthandizana pa Zinthu
zosalungama ndi zamachimo)
Kupatula oopa Mulungu (amene
adachita Chibwenzi mwa
Mulungu, pothandizana
Kukwaniritsa malamulo a
Mulungu ndi Kusiya zimene
Mulungu waletsa).
68. (Mulungu adzati): E, inu
akapolo Anga (Abwino)! Palibe
kuopa kwa inu lero lino Ndiponso
simudandaula.
69. Amene adakhulupirira
zisonyezo Zathu Ndipo adali
Asilamu (ogonjera Mulungu);
70. Lowani ku Munda Wa
mtendere, inu ndi Akazi anu
musangalatsidwa.
71. Adzakhala akupititsidwa
mbale Zagolide ndi matambula
(agolide); Zonse zokomera moyo
zidzakhala Mmenemo ndi
zokomera maso, ndipo Inu
mudzakhala mmenemo muyaya.
72. Ndipo uwu ndi munda
umene mwapatsidwa Chifukwa
cha (zabwino) zimene Munkachita.
*®sa®j&3k
$&%&$$&}$$+
Surat 43. Az-Zukhruf Juzu 25
1065
Yo^jjui ir<Jj*j\*^
73. Inu mupeza mmenemo
zipatso Zambiri zomwe Muzidya.
74. Ndithu, ochimwa (okanira)
adzakhala Mchilango cha
Jahannama muyaya;
75. Sadzapatsidwa nthawi
yopumula, Ndipo mmenemo iwo
akataya mtima (Zakupeza umoyo
wabwino).
76. Ndipo sitidawapondereze
koma Adali kudzipondereza okha.
77. Ndipo (okanira) adzaitana
Ee, iwe Maliki (yemwe ndi
Mngelo Woyang'anira moto):
"Mbuye wako atipatse imfa (kuti
Tipumule kuchilangochi!)"
Adzanena (Malik): "Ndithu, inu
Mukhala momwemo!"
78. Ndithu, tidakubweretserani
Choona; koma ambiri a inu Mudali
kuchida choona.
79. Kodi akonza bwino
chikonzero (Chawocho chomwe
ndi chiwembu Chofuna kumupha
Mtumiki{SAW})? Ndithu, nafenso
ndife okonza chikonzero Chabwino
(cholepheretsa chiwembu
Chawocho).
80. Kodi akuganiza kuti
sitikumva zobisa Zawo ndi
zonong'oneza zawo? Iyayi,
(tikuzimva zonse), ndipo Atumiki
Siirat 43. Az-Zukhruf Juzu 25
1066
ro ^j*-i
tY ^y-ji' ojj~>
Athu (angelo) ali nawo Pamodzi;
akulemba.
81. Nena (kwa omphatikiza
Mulungu ndi Mafano):
"Zikadakhala kuti (Mulungu)
Wachifundo Chambiri ali ndi
mwana, Ndiye kuti ine
ndikadakhala woyamba
Kumpembedza (mwanayo
chifukwa Chakuti ndi mwana wa
Mulungu)."
82. Mbuye wa kumwamba ndi
pansi,Mbuye wa Mpando
Wachifumu, Wapatukana ndi mbiri
zimene Akum'nenerazo (zoti
Mulungu ali ndi Mwana).
83. Asiye azingonena
zachabezo ndi Kusewera kufikira
adzakumana Ndi tsiku lawo limene
Akulonjezedwa.
84. Ndipo lye amene
akupembedzedwa Kumwamba,
ndiponso ndi lye Amene
akupembedzedwa pansi. lye Ndi
Wanzeru zakuya, Wodziwa
Kwambiri.
85. Ndipo watukuka kwambiri
Yemwe Ufumu wa kumwamba ndi
pansi ndi Pakati pazimenezi ndi
Wake. Ndiponso Kwa lye ndiko
kuli kudziwa kudza Kwa tsiku la
Kiyama; ndipo kwa lye Yekha ndi
kumene m'dzabwezedwa.
J$\&L0X?1&\£6&>
Ha*"**
Surat 43. Az-Zukhruf Juzu 25
1067
tO*j*-» tT vJytjJiSjj--
86, Ndipo omwe
akuwapembedzawo kusiya lye
(Mulungu), sangathe kupulumutsa
(Aliyense) kupatula amene
akuikira Umboni choonachi,
pom we iwo Akuchidziwa bwino.
87, Ndipo ngati utawafunsa:
"Ndani Adawalenga?" Anena
motsimikiza kuti: "Ndi Mulungu".
Nanga akutembenuzidwa Bwanji
(kusiya choona)?
88. Ndipo zonena zake
(Mneneri Muhammad {SAW}
nthawi zonse) "E, Mbuye Wanga!
Ndithu, awa ndi anthu
Osakhulupirira".
89. Choncho, akhululukire,
ndipo auze Mawu a mtendere.
Posachedwa Adzadziwa!
&l<?
i#S<&
Surat 44. Ad-Dukhan Juzu25
1068
to *j*-l
i i ObJ-oil 0jj-»
Surayi yayamba ndi kufotokoza za Qur'an kuti
idavumbulutsidwa kuchokera kwa Mulungu, mu usiku wa
Lailatul Qadir, usiku wodala, ndi cholinga chochenjeza ndi
kulongosola umodzi wa Mulungu.
Ndithu, Qur'an ndi choona chochokera kwa Mulungu. Ndipo
Surayi yafotokozanso za kuuka ponenetsa kuti palibe chikaiko
kuukako kulipo. Ndipo okanira yawadzudzula pamitsutso yawo
yopanda pake ndi kufanizira okanira a mMakka ndi anthu akale,
anthu a Farawo. Ndipo yatsimikiza ndi kulonjeza kuti tsiku la
Kiyama ndilo tsiku lawo lolonjezedwa kuweruzidwa kwawo
onse. Ndipo yafotokoza zamphoto ya osokera, ndi mphoto ya
olungama pa tsiku limeneli.
Surayi yamaliza ndi kufotokoza za Qur'an monga idayambira
kufotokoza za Qur'aniyo.
Surat 44. Ad-Dukhan Juzu 25 I 1069 I t e *j*-» £ i Oi^jJi Sjj-
Surat Ad-Dukhan XLIV
; qj^^T**-
^^
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Hd-Mim.
2. Ndikulumbirira Buku
lofotokoza Momveka.
3. Ndithu, tidaivumbulutsa
(Qur'an) mu Usiku wodala. Ife
ndithu Ndiachenjezi.
4. Mu (usiku) umenewu chinthu
Chilichonse chanzeru
chimaweruzidwa Ndi
kulongosoledwa
5. Mwa Chilamulo chochokera
kwa Ife. Ndithu, Ife Ndife otumiza
Atumiki (Kuti achenjeze anthu).
6. (Chifukwa cha) chifundo
chochokera Kwa Mbuye wako.
Ndithu lye Ngwakumva zonse,
Wodziwa kwabasi;
7. Mbuye wa thambo ndi nthaka
ndi Zapakati pake, ngati Muli
otsimikiza.
8. Palibe wopembedzedwa moona
koma lye basi.Amapereka moyo
ndikupereka Imfa, Mbuye wanu
ndi Mbuye wa makolo anu oyamba.
9. Koma iwo (okanira) ali
mchikaiko Akungosewera,
(potsatira Zilakolako zawo zoipa).
o^lc^jll^U.
&
A > r-
*^««fe£*2Ga
^%&$tyty%tf%
Surat 44. Ad-Dukhan Juzu 25 1070 * ° *j^ s * * ai^aJi 5 j>*
10. Basi, yembekezera tsiku
limene Thambo lidzadze Ndi utsi
woonekera (Konsekonse),
11. Udzawaphimba anthu onse
(ndipo Adzakhala akunena:) "Ichi
ndi chilango Chowawa.
12. E, Ambuye! Tichotsereni
Chilangochi, ndithu, Ife
tikhulupirira."
13. (Kodi lero) kukumbukira
kuwapindulira Chiyani iwo,
chikhalirecho mtumiki Wolongosola
chilichonse adawadzera.
14. Koma sadamlabadire uku
akumnena Kuti: "Waphunzitsidwa
(ndi anthu), Ndiponso wopenga."
15. Ndithu ife tichotsa
chilangocho pang'ono (Koma) inu
mubwerezanso (Machimo anu).
16. (Kumbuka, iwe Mtumiki),
tsiku limene Tidzawalanga
chilango chachikulu; Ndithu, Ife
ndife olanga.
17. Ndipo ndithu, iwo asadadze,
tidawayesa Anthu a Farawo.
Ndiponso adawadzera Mtumiki
wolemekezeka,
18. Kuti: "Ndipatseni akapolo a
Mulungu. Ndithu, ine kwa inu ndi
Mtumiki Wokhulupirika;
19. Ndipo musadzikweze kwa
Mulungu. Ndithu, ine
^^fc»$3#K
<#6&& k <j^lJ&<
^j^a8t\&a^
&&&&$&&$&
®
Siirat 44. Ad-Dukhan Juzu 25 1071 t o t£\ it d\*jS\ 5j^
ndikubweretserani Chisonyezo
choonekera.
20. Ndipo Ine ndadzitchinjiriza
ndi Mbuye Wanga ndiponso
Mbuye wanu (Ku chiwembu
chofuna kundipha) Pondigenda
(ndi miyala).
21. Ndipo ngati
simundikhulupirira, Ndipatukeni
(Musandi vutitse) . "
22. (Koma adamchitira
mtopola). Ndipo lye adaitana
Mbuye wake kuti: "Awa ndi anthu
oipa."
23. (Mulungu adamuuza kuti):
"Pita ndi akapolo Anga usiku;
ndithu, inu Mulondoledwa.
24. Ndipo isiye nyanja ili
momwemo, zii. Ndithu, iwo ndi
khamu (lankhondo) Limene
limizidwa."
25. Kodi ndi minda ingati ndi
akasupe Zomwe adazisiya
atamizidwa,
26. Ndiponso mmera ndi malo
abwino.
27. Ndi mtendere (waukulu)
umene adali Kusangalala nawo
mmenemo.
28. Umo ndi mmene zidalili.
Ndipo tidawapatsa anthu ena
zimenezo.
Surat 44. Ad-Dukhan Juzu 25
1072
Y o fr jJUi t i Ob^aJi 5jj--
29. Thambo ndi nthaka
sizidawalirire Ndipo sadapatsidwe
mpata (Wobwereranso padziko).
30. Ndipo ndithu, tidapulumutsa
ana a Israeli ku chilango Choyalutsa,
31. Chochokera kwa Farawo;
ndithu, iye Adali wodzikweza
ndiponso mmodzi Wa opyola
malire.
32. Ndipo ndithu, tidawasankha
(Ayuda Nthawi imeneyo) pamitundu
ina M'kudziwa Kwathu,
33. Ndipo tidawapatsa
zisonyezo (Kupyolera m'dzanja la
Musa) momwe Mudali mayeso
oonekera poyera kwa I wo.
34. Ndithu, awa (Akuraish)
akunena(kuti):
35. "Palibe china choposera pa
imfa yathu Yoyambayi, ndipo Ife
sitidzaukitsidwa.
36. Choncho tibweretsereni
makolo athu (Amene adafa), ngati
mukunena Zoona (kuti kuli kuuka)."
37. Kodi iwo ndi abwino (ndi
kupambana Panyonga), kapena
anthu a Tubba (Mafumu a kudziko
la Yemen) ndi Amene adalipo kale
iwo asadadze? Tidawaononga.
Ndithu, iwo adali oipa.
38. Ndipo sitidalenge thambo
ndi nthaka Ndi zimene zili pakati
paizo, Mwachibwana.
^<frW-#»$
^ifow^&^j
fess$*a
Siirat 44. Ad-Dukhan Juzu 25 1073 Y o ^jA-t
i i Ol^-oJl Sjj-*.
39. Sitidalenge ziwirizi Koma
mwachoonadi; Koma anthu ambiri
sakudziwa.
40. Ndithu, tsiku lachiweruzo
Ndiyo nthawi yawo onse (Imene
alonjezedwa),
41. Tsiku limene m'bale
sadzathandiza M'bale wake pa
chilichonse (ku Chilango cha
Mulungu), Ngakhale iwo
sadzapulumutsidwa.
42. Kupatula amene Mulungu
Adzawachitira chifiindo. Ndithu, lye
Ngwamphamvu zoposa, Wachisoni.
43. Ndithu, mtengo wa Zakkumi,
44. Ndi chakudya cha ochimwa;
45. (Kutentha kwake) ngati
mtovu Wosungunulidwa,
(wotentha Kwambiri;)
udzakhala ukuwira Mmimba,
46. Monga kuwira kwa madzi
otentha Kwambiri.
47. (Kudzanenedwa):
"Mgwireni; Mkokereni (ndi
kumponya) Pakatikati pa Jahena!
48. Kenako mthireni
pamwamba pamutu Wake chilango
chamadzi otentha!
49. (Adzauzidwa
mwachipongwe): "Lawa! Ndithu,
iwe ndiwe wamphamvu Zambiri,
Surat 44. Ad-Dukhan Juzu 25 I 1074 t o *>» it Obs-oli Sjj~-
wolemekezeka, (monga Momwe
udali kudzitamira muja).
50. Ndithu, izi ndi zimene
mudali Kuzikaikira zija!"
51. Ndithu oopa Mulungu
adzakhala Pamalo a chitetezo,
52. Mminda ndi mu akasupe;
53. Adzavala (nsalu) za silika
Wopyapyala ndi silika Wokhuthala
uku atayang'anizana (Nkhope);
54. Umo ndi mmene zidzakhalire;
ndipo Tidzawakwatitsa ndi
Ahuri'aini (Akazi okongola amaso
aakulu).
55. Mmenemo adzakhala
akuitanitsa Mtundu uliwonse wa
zipatso, Mwamtendere;
56. Mmenemo sadzalawa imfa,
kupatula Imfa yoyamba ija; ndipo
Adzawateteza Kuchilango cha
Jahena,
57. Chifukwa cha chifundo
chochokera Kwa Mbuye wako!
Kumeneko ndiko Kupambana
kwakukulu!
58. Ndithu, taifewetsa (Qur'an)
Mchiyankhulo chako (cha
Chiarabu) Kuti akumbukire.
59. Choncho yembekeza; iwonso
Akuyembekezera, (kodi ndani
Chimtsikire chilango pakati panu!).
<*? 9>l& A'*i
<oy&^*&v*w*
Surat 45. Al-Jathiyah Juzu25 1075 I to *>!
I o aJ\±-\ 5jj-*>
T^T'
*
•knfc&vF^'tti
SURAT AL-JATHIYAH XLV_
j^b- - , — - " .— -z^J^-^* 1 ^ ^ET^^Ei
Surayi ikufotokoza zamafuwa a chikhulupiriro cha Chisilamu,
mmbali zake zonse zophanuka:- Kukhulupirira Umodzi wa
Mulungu; kukhulupirira Qur'an ndi utumiki wa Mtumiki
Muhammad (SAW); kukhulupirira za tsiku lomaliza ndi kuuka
ku imfa ndi kuweruzidwa pa zochita.
Nkhani yaikulu msurayi ndi kupereka umboni ndi zisonyezo
zosonyeza Umodzi wa Mulungu.
Ndipo Surayi yayamba ndi kunena za Qur'an ndi gwero lake
lomwe ndi kwa Mulungu Wamphamvu zoposa; Wanzeru zakuya pa
zolenga Zake; Yemwe adavumbulutsa Buku Lake lolemekezeka
kuti likhale mtendere kwa anthu Ake ndikuti likhale muuni
wounikira anthu ku njira ya mtendere.
Kenako yafotokoza za zisonyezo za chilengedwe zomwe
zikusonyeza mphamvu ya Chauta ndikuti alipo; zomwenso
zikupezeka ponseponse mdziko ili lophanuka.
Ndipo yanenanso zakalengedwe ka anthu ndi nyama ndi
zolengedwa zina zosiyanasiyana zomwe zikusonya Mulungu;
monga: kusinthana usiku ndi usana, kukuntha kwa mphepo
motembenukatembenuka; ndipo zonsezi zikusonyeza mphamvu
ndi ulemelero waukulu wa Mulungu.
Surat 45. Al-Jathiyah Juzu 25 I 1076 I * ° *j*-*
i o Uli-i 5jj-*
Surat Al-Jathiyah XLV
y— ■■-■ ■■-■■
, ^^
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Hd-Mim.
2. Chivumbulutso cha Buku (ili)
Chochokera kwa Mulungu
Wamphamvu zoposa, Wanzeru
zakuya.
3. Ndithu, kuthambo ndi
m'nthaka muli Zisonyezo
(zazikulu zosonyeza kuti Mulungu
alipo) kwa okhulupirira.
4. Ndiponso mkalengedwe kanu
ndi Kalengedwe kazimene
wazifalitsa Mmenemo, (monga
zamoyo ndi Zopanda moyo), muli
zisonyezo Kwa anthu amene
akutsimikiza.
5. Ndi kusinthana kwa usana
ndi usiku, Ndi mvula imene
Mulungu Akutsitsa kuchokera
kumwamba, Akuukitsa nthaka ndi
mvulayo, itafa (Itauma), ndi
kuyendetsa mphepo
Mosinthasintha; (zonsezi) ndi
zisonyezo Kwa anthu anzeru.
6. Izi ndi aya (ndime) za
Mulungu; Tikukuwerengera iwe
mwachoonadi. Kodi ndi nkhani
yanji adzaikhulupirire Atapanda
kulabadira nkhani ya Mulunguyi
ndi aya Zake?
c&£\<£&\&\j>-
i -uft
G£i
®Wt^s$<^
^k^sj&s^m
J£5^g3^£3!^&!
»£T9»i Ju.li .* »& ' \'*.»" *'
Surat 45. Al-Jathiyah Juzu 25
1077
to *>i
£ o ajUt-l 5jj-*»
7. Kuonongeka kuli paaliyense
wopeka Zinthu, wamachimo
ambiri;
8. Amene akumva aya za
Mulungu Zikuwerengedwa kwa
iye kenako Nkumapitiriza
(chipembedzo chake
Chosalungama) uku akudzikweza
ngati Kuti sadazimve ayazo;
muuze nkhani Ya chilango
chowawa.
9. Ndipo akadziwa chinthu
chochepa Chochokera mma aya
athu, Amachichitira chipongwe;
amenewa ndi Amene adzakhala
ndi chilango Chosambula.
10. Jahannama ili
(kuwayembekezera) kuseri
Kwawo; ndipo zimene adachita
Sizidzawathandiza chilichonse,
Ngakhale atetezi amene
adadzipangira; Kusiya
Mulungu,(sadza wathandiza) ;
Ndipo adzapeza chilango
chachikulu.
11. Ichi ndi chiongoko; ndipo
amene Adakanira aya za Mbuye
wawo, Adzakhala ndi chilango
chachikulu Chochokera mchilango
chowawa.
12. Mulungu ndi Amene
wakugonjetserani Nyanja kuti
zombo ziziyenda mmenemo Mwa
lamulo Lake; ndikuti munke
3jMfcjK&
Siirat 45. Al-Jathiyah Juzu 25
1078
T© *j*-i
t © aJUrl oj^
Mufunafuna chifundo Chake kuti
Muthokoze.
13. Ndipo wakugonjetserani za
kumwamba Ndi zam'nthaka zonse
zikuchokera kwa lye. Ndithu,
mzimenezo muli Zisonyezo kwa
anthu amene Amalingalira.
14. Nena kwa amene
akhulupirira kuti Awakhululukire
amene sakuopa Masiku a Mulungu
(a chilango; Mmasiku amenewo)
kuti awalipire anthu Pa zomwe
amachita (zoipa).
15. Amene akuchita chabwino
Akudzichitira yekha ndipo amene
Akuchita zoipa, zidzakhala paiye
Mwini. Kenako Mdzabwezedwa
kwa Mbuye wanu.
16. Ndithu, tidawapatsa Ana a
Israeli Buku, ulamuliro ndi
uneneri; Ndiponso tidawapatsa
zinthu zabwino Ndikuwasankha
pamwamba pa Mitundu ina.
17. Ndipo tidawapatsa
zisonyezo Zoonekera pazinthu
zachipembedzo Chawo;
sadapatukane mpaka pomwe
Kudawadzera kudziwa, chifukwa
Chadumbo pakati pawo. Ndithu,
Mbuye wako adzalamula pakati
pawo Tsiku la Kiyama pa zimene
Adali kutsutsana.
18. Kenako tidakuika iwe pa
malamulo a zinthu za chipembedzo
h'*Mz
*'J&k
t)j«^4^8ty^^tt
w&£&&&&&
Surat 45. Al-Jathiyah Juzu 25 1079 to ^
t UUrl 5jj-*»
(Chathu). Choncho tsatira malamulo
(Athu oona) Usatsate zilakolako za
amene sadziwa (Njira yoona).
19. Ndithu, iwo (amene
akutsata njira Zonama)
sangakuthandize chilichonse Kwa
Mulungu; ndithu, achinyengo Ena
a iwo amatetezana wina ndi
Mnzake; koma Mulungu ndi
Mtetezi Wa oopa (lye potsatira
malamulo Ake Ndi kusiya
zoletsedwa).
20. Iyi (Qur'an imene
yavumbulutsidwa kwa iwe),
Ndizisonyezo kwa anthu
chiongoko ndi Chifundo kwa anthu
omwe akutsimikiza (Kuti lilipo
tsiku la chiweruzo).
21. Kodi amene adadzichitira
zoipa Akuganiza kuti tingawachite
monga Omwe adakhulupirira ndi
kuchita Zabwino kuti afanane pa
moyo wawo Ndi pa imfa yawo?)
Ndi kulamula koipa Kumene iwo
akulamula.
22. Ndipo Mulungu adalenga
thambo ndi nthaka Moona ndi kuti
mzimu uliwonse Ulipidwe zimene
udadzichitira, (Zoipa kapena
zabwino) ndipo iwo
Sadzaponderezedwa.
23. Kodi wamuona amene
wachichita Chilakolako chake
kukhala Mulungu Wake
*&£&&# &s&%
m$&ty&&&\
Surat 45. Al-Jathiyah Juzu 25 1080 I t o tjJt-i
t D UUri 3jj~*
wompembedza? Ndipo Mulungu
Wamlekerera kuti asokere,
kupyolera Mkudziwa Kwake;
ndipo wamdinda (Chidindo)
mmakutu mwake ndi mu Mtima
mwake ndi kumuika chivindikiro
Mmaso mwake. Choncho ndani
Angamuongole pambuyo pa
Mulungu? Kodi simukumbukira?
24. Ndipo (okanira kuuka ku
imfa) Adanena: "Kulibe (moyo
wina) koma Moyo wathu
womwewu wa padziko Lapansi;
timafa ndi kukhala ndi moyo;
Palibe chikutiononga koma nthawi
Basi." Koma iwo alibe kudziwa pa
Zimene akunenazo;
akungoganizira Chabe.
25. Ndipo aya Zathu
zikawerengedwa Kwa iwo
zolongosola chilichonse
Momveka, alibe mtsutso wina
koma Kunena kuti:"Tibweretsereni
atate Athu (aukitseni akhale ndi
moyo) ngati Inu muli oona!"
26. Nena (kwa iwo iwe
Mtumiki): "Mulungu
amakupatsani moyo.Kenako
Amakupatsani imfa. Kenako
Adzakusonkhanitsani tsiku la
Kiyama Lopanda chikaiko." Koma
Anthu ambiri sakudziwa.
27. Ndipo ufumu wa
kumwamba ndi pansi Ngwa
Mulungu, ndipo tsiku limene
&Z8U&&&&&&
W^a
Surat 45. Al-Jathiyah Juzu 25 I 1081 I t o ^\
i O *J\±-\ 0jj-*»
Kiyama idzachitika, (anthu)
ogwirizana Ndi zonama
adzaonongeka patsikulo.
28. Ndipo udzaliona gulu
lililonse Litagwada (uku nkhope
zili zyoli); Gulu lililonse
lidzaitanidwa ku Kaundula wake
(kukamuwerenga): "Lero
mulipidwa zimene mudali Kuchita!"
29. Uyu kaundula wathu
akunena zoona Za inu; ndithu, Ife
tidali kulemba Zimene mudali
kuchita."
30. Koma amene adakhulupirira
ndi kuchita Zabwino, Mbuye
wawo adzawalowetsa Ku chifundo
Chake; kumeneko Ndiko
kupambana koonekera.
31. Ndipo amene adakanira,
(adzauzidwa Kuti): "Kodi aya
Zanga sizidali Kuwerengedwa kwa
inu? Koma inu Mudadzikweza;
ndipo mudali anthu Oipa.
32. Ndipo kukanenedwa kuti
lonjezo la Mulungu ndiloona,
ndikuti Kiyama ilibe chikaiko,
mudali kunena, 'Sitikudziwa
Kiyama kuti nchiyani;
Tikungoganizira chabe, ndipo tilibe
Chitsimikizo (za Kiyamayo)'"
33. Choncho, kuipa kwa zimene
adachita Kudzawaonekera, ndipo
Zidzawazinga zimene ankazichitira
Chipongwe.
Surat 45. Al-Jathiyah Juzu 25
1082
lo *jJH
i O UUrl djj-»
34. Kudzanenedwanso kwa
iwowa: "Lero Tikuiwalani
(pokusiyani mchilango) Monga
momwe inu mudaiwalira
kukumana Ndi tsiku lanu ili. Ndipo
malo anu ndi Kumoto, ndipo
mulibe wokupulumutsani.
35. Zimenezi nchifukwa chakuti
inu Mudazichitira chipongwe aya
za Mulungu, Ndipo moyo wa pa
dziko udakunyengani." Choncho
lero satulutsidwa mmenemo Ndipo
madandaulo awo Savomerezedwa.
36. Choncho mbiri zonse
zabwino nza Mulungu, Mbuye
wakumwamba ndi Mbuye wa
padziko lapansi; Mbuye
Wazolengedwa.
37. Ndipo ukulu ndi Wake,
kumwamba ndi Pansi; ndipo lye
ndi Wamphamvu zoposa, Wanzeru
zakuya!
Surat 46. Al-Ahqaf Juzu 26 I 1083 I f\^i in Jifc-ty 5^
SURAT AL-AHQAF XL VI
Surayi nkhani yake ikufotokoza zakutsika kwa Qur'an
kuchokera kwa Mulungu ndi kuti nkofunika kuikhulupirira, ndi
kumkhulupirira Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale ndi
iye) ndi kukhulupiriranso tsiku lomaliza. Ndipo yatilimbikitsa
kulingalira zovuta zimene zidawapeza anthu akale amene
amanyoza Chauta pamodzi ndi aneneri Ake. Ndipo ikutiuza
kuika mtima pochitira zabwino makolo awiri (mayi ndi bambo).
Yafotokozanso nkhani ya kagulu ka ziwanda (majini) zimene
zidamvetsera Qur'an ndi kulangizana pakati pawo kumvetsera
mwachete. Ndipo zidaipeza ikuchitira umboni zimene adadza
nazo aneneri akale; ikuongolera ku ehoona ndi njira yolunjika,
ndipo zidaikhulupirira. Kenako zidaitanira ziwanda zinzawo
kuchikhulupirirocho .
Surayi yamaliza ndi nkhani yolangiza Mtumiki (madalitso
ndi mtendere zikhale ndi iye) kuti apirire pakukanidwa ndi anthu
ake ndikuti atsanzire atumiki anzake akale pakupirira masautso.
Surat 46. Al-Ahqaf Juzu 26 I 1084 I tu>i 1 1 «Jlfc-ty 5j^
SuratAl-AhqafXLVI
w,- w
mm^:: *'
j
;« :
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Hd-Mim.
2. Chivumbulutso cha Bukuli
nchochokera Kwa Mulungu
Wamphamvu zoposa, Wanzeru
zakuya.
3. Sitidangolenga thambo ndi
nthaka Ndiponso zonse zapakati pa
izo Koma mwachoonadi ndi
nyengo yoikidwa
(Yodziwika).Koma amene akana
Kukhulupirira (Mulungu)
Ngonyozera zimene achenjezedwa.
4. Nena: Tandiuzani amene
Mukuwapembedza ndi kumsiya
Mulungu, ndisonyezeni chimene
Adalenga panthaka? Kapena ali
ndi Gawo la kuthangata polenga
thambo? Ndibweretsereni Buku
limene lidadza Kale, ili lisanadze,
kapena zizindikiro Zanzeru, ngati
inu mukunena zoona.
5. Kodi ndani wasokera
kwambiri kuposa Amene
akupembedza zina kusiya Mulungu
Zomwe sizingathe kumuyankha
mpaka Tsiku la chiweruzo ndipo
izo (zimafano) Sizikuzindikira za
mapemphero awo.
oju£\<&&\&\j
— <w
®i
Surat 46. Al-Ahqaf Juzu 26 I 1085 I t n *>» f\ <Jifc*ty Sjj-
6. Ndipo anthu onse
Akadzasonkhanitsidwa Adzakhala
adani awo ndikuwakanira
Mapemphero awo.
7. Ndipo pamene
zikuwerengedwa kwa iwo Aya
Zathu zolongosola chilichonse
(cha M'chipembedzo), amene
Sadakhulupirire amanena pa
choonadi Chikawadzera: "Awa ndi
matsenga Oonekera".
8. Kapena akunena kuti:
"Waipeka (Qur'an)?Nena: "Ngati
ine ndaipeka, Ndipo simungapeze
chondithandizira Nacho kwa
Mulungu (ku chilango Chake)".
lye ndiwodziwa kwambiri Zimene
mukuzijijirikira. lye Akukwana
kukhala mboni pakati pa ine Ndi
inu ndipo lye Ngokhululuka
Kwabasi, Wachisoni.
9. Nena: "Ine sindine woyamba
pa aneneri, Ndipo sindikudziwa
zimene zidzachitike Kwa ine
ngakhale kwa inu. Sinditsatira
Koma zokhazo zimene
zikuvumbulutsidwa Kwa ine;
ndipo ine sindili kanthu koma
Mchenjezi wolongosola
(Zofunika)".
10. Nena: "Tandiuzani, ngati
(Buku ili) Litachokera kwa
Mulungu, ndipo inu Nkulikana uku
mboni yochokera mu Ana a Israeli
Surat 46. Al-Ahqaf Juzu 26
1086
n ^jJt-i t% uiu^Si 5j>*
itachitira umboni kuti Idaliona
longa limeneli, ndipo iwo
Nkulikhulupirira (Bukuli) pomwe
inu Mwadzitukumula, ndithu,
Mulungu Saongola anthu
osalungama.
11. Ndipo amene
sadakhulupirire adanena Kwa
amene adakhulupirira:
"(Chipembedzo ichi) chikadakhala
Chabwino, awa sakadakhala
otsogola ku Chimenechi pa ife."
Ndipo chifukwa Choti sadaongoke
nalo (Bukuli), akhala Akunena:
"Hi ndi bodza lakale."
12. Ndipo lisadadze ili lidalipo
Buku la Musa monga mtsogoleri
Ndi chifundo. Ndipo Buku ili
likuikira Umboni (za Bukulo)
m'chiyankhulo cha Chiarabu kuti
liwachenjeze amene Adzichitira
okha chinyengo, ndi kuti Likhale
uthenga wabwino kwa ochita
Zabwino.
13. Ndithu, amene anena (kuti):
"Mbuye Wathu ndi Mulungu".
Kenako Ndikulungama,
sadzakhala ndi Mantha (tsiku
lakufa kwawo ngakhale Pambuyo
pake), ndiponso Sadzadandaula.
14. Iwo wo ndi wo anthu aku
Jannat Adzakhala kumeneko
Muyaya kukhala mphoto ya
Zimene amachita.
''*
Surat 46. AI-Ahqaf Juzu 26
1087
Y 1 *j*-l in iJlfc-ty 5jj~-
15. Ndipo tamulangiza munthu
kuchitira zabwino Makolo ake.
Mayi wake adatenga Pathupi pake
mwamasautso; ndipo Adam'bala
mwamasautso. Kutenga Pakati
pake ndi kumsiitsa kuyamwa Ndi
miyezi makumi atatu. Kufikira
Atakula msimkhu nkukwana zaka
Makumi anayi, (akakhala mwana
Wabwino) amanena: "O, Mbuye
wanga! Ndilimbikitseni kuthokoza
mtendere Warm umene
mwandipatsa pamodzi ndi Makolo
anga, ndipo ndilimbitseni kuti
Ndizichita zabwino zimene (Inu)
Muziyanja ndipo ndikonzereni ndi
Kundilungamitsira ana anga. Ine
Ndatembenukira kwa Inu;
ndiponso Ine ndine m'modzi mwa
ogonjera (Inu)."
16. Iwowo ndiamene
tikuwalandira Zabwino zimene
adachita ndipo Tikuwakhululukira
zolakwa zawo. Adzakhala m'gulu
la anthu a ku Jannat. Hi ndi lonjezo
loona lorn we Adalonjezedwa.
17. Tsono (mwana woipa)
amene akunena Kwa makolo ake,
(akamuitanira ku Chikhulupiriro
kuti) "Ndithu ndinu Oipa (pa
zimene mukundiitanirazi)!
Mukundilonjeza kuti
ndidzatulutsidwa Mmanda ndili
wamoyo, chikhalirecho Mibadwo
ndi mibadwo idapita Kumanda ine
>i*
Surat 46. Al-Ahqaf Juzu 26
1088
Yn ^jA-l i*\ uJtf^Sl ijy*
kulibe (koma mpaka lero
Siidauke)?" Ndipo uku makolo ake
Akupempha Mulungu kuti
Ampulumutse ndi kumuongola ndi
Kunena kwa iye: "Tsoka kwa iwe
Khulupirira (Mulungu ndi kuuka
ku Imfa, ngati sutero
waonongeka). Ndithu, Lonjezo la
Mulungu ndiloona." Koma Iye
nkumanena (kuti): "Sikanthu izi
Mukuzinena koma ndi nthano Za
anthu akale."
18. Iwowo ndiamene
latsimikizika pa iwo Liwu (la
chilango) pamodzi ndi Mibadwo
ya ziwanda ndi anthu, imene
Idanka kale iwo kulibe; ndithu,
iwo Adali otaika.
19. Ndipo aliyense
wokhulupirira Adzakhala ndi
nyota molingana ndi Zimene
adachita, ndi kuti (Mulungu)
Awalipire zochita zawo ndipo iwo
Sadzaponderezedwa.
20. Ndipo (akumbutse za) tsiku
limene Adzaikidwa pafupi ndi
moto amene Sadakhulupirire
(adzawauza kuti) "Mudaononga
zabwino zanu mmoyo Wadziko
lapansi, (choncho lero
Simuzipezanso),ndipo inu
mudasangalala Nazo zimenezo,
choncho lero Mupatsidwa chilango
chokusambulani Chifukwa cha
kudzikweza kwanu Padziko
Surat 46. AI-Ahqaf Juzu 26
1089
n *>i t n <Ji&*ty s^
popanda choona, ndiponso
Chifukwa cha kulakwa kwanu."
21. Ndipo kumbuka za m'bale
wa Adi, (Mtumiki Hud) pamene
adachenjeza Anthu ake kudziko la
milu ya Mchenga. Ndithu,
adaliponso achenjezi lye asadadze
ndiponso iye atapita. (lye
adawauza anthu ake):
"Musampembedze aliyense koma
Mulungu; ndithu ine
ndikukuoperani Chilango cha tsiku
lalikulu." 1
22. Adanena: "Ha! Kodi
watidzera kuti Utipatule ku
milungu yathu? Choncho
Tibweretsere zimene
ukutilonjezazo Ngati uli mwa
Onena zoona."
23. Adanena (Hud): "Ndithu
kudziwa (Kwenikweni kwa
zimenezo) kuli kwa Mulungu;
ndipo ine ndikungofikitsa Kwa inu
zimene ndatumidwa koma ine
Ndikukuonani kuti inu ndinu anthu
Amene mukuchita (zinthu za)
umbuli!.
24. Kenako pamene adauona
mtambo Ukulunjika ku zigwa
zawo, adanena, "Mtambo uwu ndi
wotivumbwitsira Mvula!"
(Adauzidwa): "Iyayi, Chimenechi
1 Dziko la milu ya mchenga: Awa ndi malo
mzinda wa Hadhwara Mauti pakati pa dziko la
\jo^x>y>\ teK?** As^i^
omwe akupezeka kummwera kwa
Omman ndi Yemen kwao kwa Adi.
Surat 46. Al-Ahqaf Juzu 26
1090
Yn frjJH tnJu^is^
ndichimene Mudachifulumizitsa
chija (kuti chidze Mwachangu!)
Mphepo (ya mkutho) Yomwe
mkati mwake muli chilango
Chowawa!
25. Yoononga chinthu
chilichonse mwa Lamulo la Mbuye
wake!" Kenako adali
Osaonedwanso, kupatula nyumba
zawo (Ndizimene zidatsalira).
Umo Ndim'mene timawalipirira
anthu oipa.
26. Ndipo ndithu, tidawapatsa
mphamvu Yochitira zinthu ndi
kukhala ndi chuma Chambiri ndi
moyo wautali zomwe
Sitidakupatseni inu (Akuraishi)
ndipo Tidawapatsa makutu ndi
maso ndi Mitima,koma makutu
awo ndi maso Awo ndi mitima
yawo sizidawapindulire
Chilichonse chifukwa chotsutsa
aya za Mulungu; ndipo
zidawazinga zomwe Adali
kuzichitira chipongwe.
27. Ndithu, tidaiononga midzi
imene Yakuzungulirani; ndipo
Tidawafotokozera momveka aya
Zathu Kuti abwerere.
28. Chifukwa chiyani
siidawapulumutse Milungu imene
adaipangayo kusiya Mulungu kuti
iwayandikitse kwa lye (Mulungu)?
Koma idasoweka kwa iwo (Pomwe
Surat 46. AI-Ahqaf Juzu 26
1091
Y*\ s.jA-1 t % <Jlfc*ty Sjj-
iwo adali pamavuto ofuna
Kulandira chithandizo). Ndipo
Zimenezo ndizo zotsatira zabodza
lawo Ndi zomwe adali kupeka.
29. Ndipo (kumbuka iwe
Mtumiki{SAW}) Pamene
tidakutumizira gulu la ziwanda
(Majini) kudzamvera Qur'an ndipo
pamene Izo zidafika pamalopo
zidanena pakati Pawo: "Khalani
chete!" Pomwe Kuwerenga (kwa
Qur'an) kudatha, Zidabwerera ku
mtundu wawo Kukawachenjeza
(za chilango cha Mulungu).
30. Zidanena: "E, inu anzathu!
Ife tamva (Zowerengedwa) za
m'buku (Lolemekezeka) lomwe
Lavumbulutsidwa pambuyo pa
Musa, Loikira umboni zimene
Zidalitsogolera; likuongolera ku
choona Ndi kunjira yolunjika".
31. "E, inu anzathu!
Muvomereni woitana Wa
Mulungu, ndipo mkhulupirireni;
(Mulungu) akukhululukirani
machimo Anu ndi kukutetezani ku
chilango Chowawa.
32. Ngati wina samuvomera
woitanira Kwa Mulungu,
sangamulepheretse (Mulungu)
padziko (akafuna kumuchita
Kanthu), ndipo iye alibe atetezi
ena Kupatula Iye (Mulungu). Otere
akusokera Koonekera poyera."
Surat 46. Al-Ahqaf Juzu 26
1092
Y 1 *>■» 1 1 <Jlfc^|l 5^
33. Kodi iwo saona kuti
Mulungu Amene Adalenga thambo
ndi nthaka, ndipo Sadatope
pozilenga, ndi Wakutha
Kuwaukitsa anthu ku imfa? Inde,
ndithu lye Ngokhoza kuchita
chilichonse
34. Ndipo (akumbutse za) tsiku
limene Adzaperekedwa ku moto
amene Sadakhulupirire (uku
akuuzidwa): "Kodi izi sizoona?"
Adzanena: "Inde, Pali Mbuye
wathu !" (Mulungu) adzanena:
"Choncho, Lawani chilango
chifukwa cha kukana (Choonadi)
kwanu."
35. Choncho pirira
(Mtumiki{SAW}) monga
Adapirira aneneri, eni mphamvu
ndi Kulimba pa chipembedzo,
(monga Nuh, Ibrahimu, Musa ndi
Isa); ndipo Usawachitire changu.
Tsiku limene Adzaziona zimene
adalonjezedwa Kudzakhala monga
iwo sadakhalitse Padziko koma
ngati adakhala ola Limodzi lokha
lamasana. (Zomwe
Mukuuzidwazi) ndi ulaliki
okwana. Palibe adzaonongedwe
(ndi Chilango cha Mulungu),
kupatula anthu Ochimwa (otuluka
m'chilamulo cha Mulungu).
Surat 47. Muhammad Juzu 26
1093
y\ tjk-\
i v ju^ a jj--
SURAT MUHAMMAD XL VII
Surayi yalongosola kumayambiriro kwake, kuti ndithu,
Mulungu adaononga zochita za osakhulupirira chifukwa cha
kutsata zonama kwawo. Ndipo wawafafanizira okhulupirira
machimo awo chifukwa chotsatira zoona.
Yafotokozanso mwatsatanetsatane kuti kuteteza choona
nkofunika; kutinso mphoto ya ntchito imeneyo, pa tsiku
lomaliza, ndi kulowa ku mtendere. Ndipo yawalimbikitsa
okhulupirira kuti achipulumutse chipembedzo cha Mulungu, ndi
kumenya nkhondo panjira yake. Kenako yafotokozanso kuti
anthu achinyengo, akapatuka pa chikhulupiriro, amaononga ndi
kuthetsa chibale padziko.
Ndipo yachenjeza za a chinyengo kuti anthu oterewa
asakhale pakati pa anthu okhulupirira, chifukwa iwo samvera
mawu a Mulungu kuti awalimbikitse mtima, koma okonda
ukazitape basi. Ndipo yawaopseza achinyengo kuti Mulungu
aulula za kaduka kawo komwe kali m'mitima mwawo kwa
Mtumiki Wake.
Surayi yaletsa Asilamu kufooka pankhondo yolimbana ndi
anthu osakhulupirira pomwe iwo ngapamwamba ndikutinso
Mulungu ali nawo pamodzi. Ndipo sadzawachepetsera mphoto
yantchito zawo.
Surat 47. Muhammad Juzu 26
1094
rn *>i
£ V JU£ 5 j j**
Surat Muhammad XL VII
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Amene adam'kana (Mulungu
ndi Mthenga Wake) ndi
kutsekereza anthu Kuyenda panjira
ya Mulungu (Powaletsa kulowa
m'Chisilamu), Mulungu waononga
zonse zabwino Zimene adachita .
2. Ndipo amene akhulupirira
nkumachita Zabwino,
nkuzikhulupirira zimene
Zavumbulutsidwa kwa
Muhammad(SAW), Zimene zili
zoona zochokera kwa Mbuye
wawo, wawafafanizira zolakwa
Zawo, ndipo awakonzera
chikhalidwe Chawo (patsiku
lomaliza ndi padziko Lapansi).
3. Zimenezi nchifukwa chakuti
amene Sadakhulupirire adatsata
chonama, Ndipo amene
adakhulupirira adatsatira Choonadi
chochokera kwa Mbuye wawo.
M'menemu ndim'mene Mulungu
Akulongosolera kwa anthu
Pamakhalidwe awo (kuti alingalire
ndi Kupeza phunziro).
4. Mukamakumana nawo
pankhondo Amene sanakhulupirire
amenyeni Makosi awo (aduleni),
mpaka Mwafooketse pochuluka
w.
.-1 \&&Ste ,
oj&3\^%&\j
-&
Surat 47. Muhammad Juzu 26
1095
yi *>i
l V >U£ 6jj~t
ophedwa Mwa iwo; kenako
amangeni ndi Zingwe (otsalawo).
Ngati mutafuna Kuwamasula
popanda dipo kapena kuti apereke
Dipo, (zili kwa inu).Kufikira
nkhondo itatha. Limenelo ndi
lamulo la Mulungu. Ndithu,
Mulungu akadafuna akadathana
nawo lye mwini powaononga onse
psiti; Koma (wakulamulani kuti
muchite Nkhondo) ncholinga choti
awayese mayeso ena Ainu pa ena
(okhulupirira pa okanitsitsawo).
Ndipo amene aphedwa panjira ya
Mulungu, ntchito yawo
sadzaipititsa Pachabe.
5. Awaongolera (ku zimene
Zingawapindulitse pa dziko
lapansi Ndi patsiku lomaliza) ndi
kuwakonzera Zinthu zawo ndi
chikhalidwe chawo,
6. Ndi kukawalowetsa ku Munda
wa Mtendere umene Adawadziwitsa.
7. E, inu amene
mwakhulupirira! Ngati Muteteza
chipembedzo cha
Mulungu,(Mulungu)
adzakutetezani (Kwa adani anu)
ndi kulimbikitsa Mapazi anu
(pankhondo).
8. Koma amene akana
(Mulungu ndi Aya Zake)
kuwonongeka nkwawo Ndipo
awaonongera zochita zawo.
ty$K7^Z$>£i*
©.
ox&qm
u5j
Surat 47. Muhammad Juzu 26
1096 | tl ^j*-i
i V ju^ «j j--
9. Zimenezo nchifukwa chakuti
iwo Azida zomwe Mulungu
adavumbulutsa (Monga Qur'an ndi
malamulo ake;) Choncho
waziononga Zochita zawo.
10. Kodi sadayendeyende
padziko nkuona Kuti adali bwanji
mapeto a amene Adawatsogolera
(monga Adi ndi Samudi, ndi anthu
a Luti ndi ena Otero)? Mulungu
adawaononga psiti, Ndipo chilango
ngati chimenecho Chidzakhalanso
kwa osakhulupirira.
11. Zimenezo nchifukwa
chakuti Mulungu Ndi Mtetezi wa
amene akhulupirira, Koma
osakhulupirira alibe mtetezi.
12. Ndithu, Mulungu
adzawalowetsa ku Minda ya
mtendere amene Adakhulupirira
ndi kuchita zabwino, (Momwe)
pansi pake ikuyenda Mitsinje;
koma amene sadakhulupirire
Akusangalala (padziko lapansi) ndi
Kudya momwe zidyera ziweto
(Popanda lingaliro lililonse
kupatula Lingaliro la mimba zawo
ndi Kukwaniritsa zilakolako za
Chilengedwe chawo); Ndipo Moto
ndi wo malo awo.
13. Ndi ambiri mwa eni
mizinda (yakale) omwe Adali
amphamvu kuposa eni mzinda
Wakowu umene akutulutsamo (eni
©*us&3#
Surat 47. Muhammad Juzu 26
1097
Tl *>l
t V -U* Sj j~-
ake,) Tidawaononga (ndi zilango
Zosiyanasiyana) koma padalibe
Wowateteza (kwa Ife).
14. Kodi angafanane, (polandira
mphoto,) Amene ali ndi umboni
wodziwika wochokera Kwa
Mbuye wake, (kotero kuti
Nkumamumvera, ndi amene
Wakometsedwa ndi zochita zake
zoipa Natsatira zilakolako zawo.
15. Fanizo la Munda wa
mtendere (Janna) Umene
alonjezedwa oopa Mulungu
(Potsatira malamulo Ake ndi
kusiya Zoletsedwa, udzakhala
chonchi): M'menemo muli
mitsinje yamadzi Osasintha fungo
lake; ndi mitsinje Yamkaka
wosasasa mkakomedwe kake; Ndi
mitsinje yavinyo wokoma Kwa
akumwa ndi mitsinje ya uchi
Woyeretsedwa (kuphula), ndiponso
Iwo adzapeza m'menemo mtundu
Uliwonse wazipatso ndi
chikhululuko Chochokera kwa
Mbuye wawo. Angafanane ndi
wokhala muyaya Kumoto, ndi
kumwetsedwa madzi Owira omwe
akadula matumbo awo?
16. Ndipo ena mwa iwo (okana
Mulungu) Amamvetsera kwa iwe,
(popanda Kupindula chilichonse),
ndipo Akachoka pamalo pakopo,
amanena Kwa amene apatsidwa
nzeru (mwa Omtsatira ake): "Kodi
Surat 47. Muhammad Juzu 26
1098
n fj*-»
£ V *W£ 5 j j-*»
(Mtumiki) Wanena chiyani
posachedwapa?" Iwowo Ndiamene
Mulungu wawadinda M'mitima
mwawo (ndi chidindo Chokana
Mulungu), ndipo amatsatira
Zilakolako zawo (zachabe).
17. Ndipo amene aongoka,
(Mulungu) Amawaonjezera
chiongoko ndi Kuwapatsa kuopa
kwawo (Komuopa Mulungu).
18. Palibe chimene
akuyembekezera tsiku
Lachiweruziro limene liwadzere
Mwadzidzidzi (uku iwo ali
otanganidwa Ndi zam'dziko)?
Ndithu zizindikiro zake Zadza
kale; kodi kudzawapindulira
chiyani Kukumbuka kwawo
likadzawadzera (Tsikulo)?
19. Dziwa kuti palibe
wompembedza M'choonadi koma
Mulungu, ndipo Pempha
chikhululuko pa zolakwa zako Ndi
zolakwa za okhulupirira achimuna
ndi Achikazi; ndipo Mulungu
akudziwa malo Anu opita ndi
kubwera ndi malo anu
Wokhazikika.
20. Ndipo amene akhulupirira
akunena (Chifukwa cha mazunzo
omwe Amawapeza kuchokera kwa
Osakhulupirira kuti) kodi
nchifukwaNinji
siikuvumbulutsidwa sura
9 ? £\<* ** *Z'\<\ 9 'C 9 L"'>4i'
Siirat 47. Muhammad Juzu 26
1099
y*\ *j*-i
t V JU^ o jj-»
(Yotiloleza kumenyana ndi
Osakhulupirira Mulungu amene
Akutiputa)? Koma
ikavumbulutsidwa Sura
yokhazikika (lamulo lake),ndipo
Mkati mwake ndi kutchulidwa
nkhani Zankhondo, uwaona amene
ali ndi Matenda m'mitima mwawo
Akukuyang'ana m'mayang'anidwe
a Yemwe akukomoka ndi imfa,
(chifukwa Cha kulida lamulo
lomenyana ndi Osakhulupirira),
basi kuonongeka ndi Kwawo.
21. (Zofunika ndi) kumvera ndi
mawu Abwino ndi kuti chinthu
Chikatsimikizika (achichite). Ngati
Akadamvera Mulungu, ndithu
zikadakhala Zabwino kwa iwo.
22. Mwina mwake inu
mukanyoza (Chisilamu),
mubwerera m'mbuyo ku Zomwe
mudali nazo (m'nthawi ya Umbuli)
monga kuononga padziko Ndi
machimo) ndi kudula chibale chanu.
23. Oterewo ndiamene
Mulungu Wawatemberera ndi
kuwagonthetsa Ndi kuwachititsa
khungu maso awo.
24. Kodi sakuilingalira Qur'an?
Kapena m'mitima mwawo
M'motsekedwa ndi maloko ake?
25. Ndithu, amene akubwerera
m'mbuyo (Kusiya chipembedzo
chawo Nkubwerera ku
^5ift£Jt
\\ 9 > Z J ~ 9< 9 l9*'£ 9, 9 l9,s \'<
Surat 47. Muhammad Juzu 26
1100
tn *>i
£ V *U* 5 j j-»
zosakhulupirira Mulungu)
chiongoko chitawaonekera Poyera
Satana ndiamene wawanyenga,
Ndipo Mulungu akuwapatsa nthawi.
26. Zimenezo nkaamba kakuti
iwo adanena Kwa omwe amada
zimene Mulungu Wavumbulutsa
(kuti): "Tidzakumverani M'zinthu
zina (zimene mukutsutsana Ndi
Mtumiki{SAW})" Ndipo Mulungu
Akudziwa zobisika zawo.
27. Kodi adzakhala bwanji
pamene Angelo Azidzatenga
mizimu yawo uku Akumenya
nkhope zawo ndi misana Yawo?
28. Zimenezi (imfa yoopsayi)
nkaamba Kakuti iwo adatsata
zomwe zidakwiitsa Mulungu ndi
kuda zomusangalatsa (Mulungu);
choncho adaziwononga Zochita
zawo.
29. Kodi amene ali ndi matenda
m'mitima Mwawo akuganiza kuti
Mulungu Sangaonetsere poyera
kaduka kawo?
30. Ndipo tikadafuna
tikadakuonetsa iwo (Amene
akuchitira kaduka Chisilamu)
Ndipo ukadawadziwa ndi
zizindikiro Zawo. Koma ndithu,
uwadziwa M'kayankhulidwe
(kawo) kokometsa Ndipo Mulungu
akudziwa zochita Zanu zonse.
®#$;
Surat 47. Muhammad Juzu 26
1101 "*>»
tv
d J>-»
31. Ndipo ndithu tikuyesani
mayeso mpaka Tiwaonetsere
poyera (adziwike) amene
Akumenya nkhondo mwa inu
(Chifukwa cha dini) ndi opirira
(Pamavuto); ndi kuzionetsera
poyera Nkhani zanu (zochita zanu).
32. Ndithu,amene akana
(Mtumiki{SAW})Ndi
kuwatsekereza anthu kunjira ya
Mulungu, ndi kutsutsana ndi
Mtumiki Chiongoko chitadziwika
kwa iwo, Sangamsautse Mulungu
ndi chilichonse, Koma
adzawaonongera ntchito Zawo.
33. E, inu amene
mwakhulupirira! Mverani
Mulungu ndiponso mverani
mtumiki (Wake) ndipo
musaononge zochita zanu.
34. Ndithu, amene
sadakhulupirire ndi Kwatsekereza
anthu kunjira ya Mulungu, kenako
nkufa uku ali Osakhulupirira
Mulungu Sadzawakhululukira
(zolakwa zawo).
35. Musafooke ndi kufuna
chimvano, (Koma menyanani ndi
adani anu); inu Ndinu opambana.
Ndipo Mulungu ali nanu
(Pokuthangatani ndi
kukupulumutsani,) Ndipo
sakuchepetserani (mphoto ya)
Ntchito zanu.
Surat 47. Muhammad Juzu 26
1102
n *>i
£ V *U£ dj j-j
36. Ndithu, moyo wapadziko
ndi masewero Ndiponso ndi
wachabechabe. Ndipo Ngati
mukhulupirira ndi kudzipatula
Kumachimo (Mulungu) akupatsani
Malipiro anu, ndipo
sakukupemphani Chuma chanu.
37. Ngati akadachifuna
(kuchokera) kwa inu Chumacho
ndi kukuchulukitsirani
(Chopereka),mukadachita
umbombo (Ndi chumacho), ndipo
akadatulutsira (Poyera) kaduka
kanu.
38. Ha! Ndinu amene
mukuitanidwa kuti Mupereke
(chuma) munjira ya Mulungu.
Koma alipo ena a inu akuumira
Ndipo amene akuumira akuzimana
yekha. Mulungu
Ngwachikwanekwane ndipo inu
Ndinu amphawi .Ngati munyoza
(Chisilamu) Ndi kubwerera
m'mbuyo posakhulupirira)
Mulungu adzabweretsa m'malo
mwanu Anthu ena; iwo sadzakhala
ngati inu.
®$g\
Surat 48. Al-Fath Juzu 26
1103
TltjJt-t tAj^lSj^
Surayi koyambirira kwake ikufotokoza za kupambana
kwakukulu kumene Mulungu adamukonzera Mtumiki Wake
(madalitso ndi mtendere zikhale naye) ndi zotsatira zikuluzikulu
m'kufala kwa Chisilamu, ndi Asilamu kukhala ndi mphamvu,
ndiponso m'mene Mulungu adalimbikitsira okhulupirira mitima
kuti chikhulupiriro chawo chiwonjezeke.
Ikufotokozanso za chilango cha anthu achinyengo ndi
ophatikiza Mulungu ndi mafano ndi kutinso Muhammadi
(madalitso ndi mtendere zikhale naye) adatumizidwa kuti akhale
mboni ndi kulengeza nkhani yabwino kuti anthu akhulupirire
mwa Mulungu. Ndipo kenako Surayi yafotokoza za malonjezo a
anthu oona omwe adalonjezana ndi Mtumiki kupita ku nkhondo
pachifukwa chakuti ankaganizira kuti Mulungu sakampulumutsa.
Yafotokozanso za kufuna kwawo kutuluka kupita ku
nkhondo pamodzi ndi Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale
naye) ncholinga chokapeza chuma chosiyidwa ndi adani. Ndipo
kenako yafotokozanso kuti iwo adzaitanidwa kuti akamenyane
ndi anthu amphamvu, ndipo yanenetsa kuti palibe uchimo
kusapita kunkhondo ngati pali zifukwa zomveka.
Kenako yafotokoza za kukula kwa mphoto ya omwe
adam'lonjeza Chauta pa lonjezo la Rizuwani. Ndipo
yafotokozanso kuti osakhulupirirawo akadayesera kumenyana
ndi Asilamu akadathawa. Ndipo kenako yanenanso za cholinga
cha Mulungu chanzeru powamanga manja osakhulupirira kuti
asamenye Asilamu ndi kumanganso manja a Asilamu kuti
asamenye osakhulupirirawo pa tsiku logonjetsa mzinda wa Makka.
Ndipo Surayi yanenetsa kuti ndithu, Mulungu adamtsimikizira
Mtumiki Wake zamaloto ake olowa mu Msikiti wopatulika. Ndi
kuti Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale naye) pamodzi
ndi omtsatira adali a mphamvu kwa anthu osakhulupirira Chauta.
Surat 48. Al-Fath Juzu 26
1104
ti *>i
1A jaflJl 0jj-*>
I wo wokha Asilamu adali kuchitirana chifundo pakati pawo.
Choncho m'surayi Mulungu akumuuza Mneneri Wake
(madalitso ndi mtendere zikhale naye) kuti ampatsa kupambana
kwakukulu chifukwa chochita pangano limeneli. Umo ndi
mom we zidalili; panganoli lidachititsa Asilamu kuti agonjetse
mzinda wa Makka. Ndipo pasanathe zaka ziwiri Mzinda wonse
wa Makka udagonjera Chisilamu, kenako chilumba chonse cha
Arabia chidagonjera chipembedzochi.
Pomaliza yafotokoza zizindikiro za okhulupirira (Asilamu)
ndi makhalidwe awo amene amapezeka m'buku la Chipangano
chakale ndi Chipangano chatsopano. Ndipo Mulungu walonjeza
kwa okhulupirira, ochita zabwino chikhululuko ndi mphoto
yaikulu.
Siirat 48. Al-Fath Juzu 26 1 105 t n *>i
t A jcuilt ijj**>
Surat Al-Fath XLVIII
^W.;
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Ndithu, takugonjetsera (iwe
Mtumiki{SAW}mzinda wa
Makka) Kugonjetsa kwakukulu
koonekera Poyera; 1
2. Kuti Mulungu
akukhululukire zolakwa Zako
zapatsogolo ndi zapambuyo, ndi
Kukukwaniritsira mtendere Wake,
ndi Kukuongolera kunjira
yolunjika;
3. Ndikuti Mulungu akuteteze
ndi Chitetezo champhamvu.
4. lye ndiamene adatsitsa
chikhazikiko (Kudekha) m'mitima
mwa okhulupirira Kuti awonjezera
chikhulupiriro Pachikhulupiro
chawo. Makamu Ankhondo
^=
qWUfc^^
-Ci
as$sti®&$
*&
><
1 M'chaka cha chisanu ndi chimodzi chisamukire Mtumiki(SAW), Mtumiki
(madalitso ndi mtendere zikhale naye) adapita ku Makka kuchokera ku Madina
pamodzi ndi omtsatira ake kuti akachite Umura imene ndi Haji yaing'ono.
Koma atayandikira ku Makka, Akuraishi adamuletsa kulowa mumzindamo kuti
asachite mapemphero a Umura. Ndipo atakambiranakambirana adamvana
mfundo zingapo, zina mwa izo ndi:-
(i) Asamenyane nthawi imeneyo.
(ii) Abwerere ndipo adzabwere chaka chotsatiracho mwezi wonga umenewo
kudzachita mapemphero. Panthawiyo sadzawaletsa kulowa mu mzindawo.
(iii) Asiye kumenyana pakati pawo kwa zaka khumi, ndi kumayenderana
m'mene angafunire; Akuraishi azipita ku Madina ngati atafuna, popanda
kuzunzidwa.
(iv) Mafuko ena a Arabu adaioledwa kulowa nawo m'pangano limeneli kuti
asamthire nkhondo Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye), ndipo
iyenso asawathire nkhondo.
Surat 48. Al-Fath Juzu 26
1106
y\ *>»
t A jiaJl Sjj-*
akumwamba ndi pansi, Nga
Mulungu, (monga Angelo,
Ziwanda, nyama ziphaliwali,
mphepo Yamkutho ndi zivomerezi
ndi zina Zotero); ndipo Mulungu
Ngodziwa Chilichonse, ndiponso
Wanzeru zakuya;
5. (Wachita izi) kuti okhulupirira
achimuna Ndi achikazi
akawalowetse m'minda Yomwe
pansi pake ikuyenda mitsinje;
Adzakhala muyaya m'menemo,
Ndi kuti awafafanizire zolakwa
zawo; Kumeneko ndiko kupambana
Kwakukulu kwa Mulungu.
6. Ndi kuti awalange
achiphamaso Achimuna ndi
achikazi ndi Omphatikiza
Mulungu achimuna ndi Achikazi
oganizira Mulungu maganizo
Achabe. Kutembenuka koipa kuli
kwa Iwo ndipo Mulungu
wawakwiyira Ndiponso
wawatemberera ndi Kuwakonzera
Jahannamu.Ndipo kumeneko
nkobwerera koipa.
7. Ndipo magulu ankhondo
akumwamba ndi Pansi nga
Mulungu; ndipo Mulungu Ndi
Wamphamvu zoposa, Wa nzeru
Zakuya.
8. Ndithu, takutumiza kuti
ukhale mboni Ndi wolengeza
nkhani zabwino Ndiponso
mchenjezi.
&s$ss&$&
Surat 48. Al-Fath Juzu 26
1107
M *j*-»
i A jsdil Sjj-u
9. Ncholinga choti
mumkhulupirire Mulungu ndi
Mtumiki Wake, ndi kuti
Mumtukule ndi kumulemekeza
(Mtumiki) ndi kutinso
mumtamande (Mulungu) m'mawa
ndi madzulo.
10. Ndithu, amene
akukulonjeza, ndiye Kuti
akulonjeza Mulungu. Dzanja la
Mulungu lili pamwamba pa manja
awo. Amene ati aswe lonjezo, ndiye
kuti Wadziswera yekha (mavuto ali
pa lye). Koma yemwe akwaniritse
Zomwe adalonjeza kwa Mulungu,
amulipira malipiro aakulu.
11. Adzanena kwa iwe Arabu
Am'midzi otsala (ku nkhondo,
amene Adalibe zifukwa zomveka
m'kutsala Kwawo): Chuma ndi
ana athu Zidatitangwanitsa;
choncho Tipemphereni
chikhululuko. Akunena Ndi
malirime awo (mawu) omwe
M'mitima mwawo mulibe. Nena:
"Kodi ndani angathe
kukuthandizani Chilichonse kwa
Mulungu ngati atafuna
Kukupatsani masautso, kapena
atafuna Kukupatsani zabwino?
Koma Mulungu Akudziwa zonse
zimene mukuchita.
12. Koma mudali kuganiza kuti
Mtumiki Ndi okhulupirira
sabwereranso ku maanja Awo,
)y^i
Surat 48. Al-Fath Juzu 26
1108
n frj*-i
t A jttiJi 0jj-»
(akaphedwa konko); zimenezo
Zidakukondweretsani m'mitima
Mwanu,ndipo mumaganiza ganizo
Loipa; ndipo mudali anthu
oonongeka."
13. Ndipo amene sakhulupirira
Mulungu Ndi Mtumiki Wake,
ndithu, Ife Tawakonzera okanira
chilango chamoto Woyaka.
14. Ndipo ufumu wakumwamba
ndi pansi ngwa Mulungu.
Amakhululukira amene Wamfuna
(ngati atatembenukira kwa lye) ndi
kumlanga amene wamfuna (Ngati
sanatembenukire kwa lye). Ndipo
Mulungu Ngokhululuka kwambiri
Ngwachisoni.
15. Otsala (kunkhondo) aja,
mukapita Kukatenga zotola za a
nkhondo, Adzanena: "Tilekeni
tikutsatileni." Akufuna kuti asinthe
mawu a Mulungu. Nena:
"Simutitsatira! Umo ndimo
Mulungu adanenera kale." (Apo)
Adzanena (kuti): "Koma
mukutichitira Dumbo." Iyayi,
koma nzochepa zomwe Adali
kuzindikira.
16. Nena kwa otsala
(kunkhondo) mwa Arabu a
m'midzi: Mudzaitanidwa
(kukamenyana) ndi Anthu eni
mphamvu zaukali; Mudzamenyana
nawo kapena adzagonja (Ndi
*$&$&*&$&%>
®\
Surat 48. Al-Fath Juzu 26
1109
r\ *>i
i A jaiJl Sj j-*»
kulowa m'Chisilamu). Ngati
Mudzamvera, Mulungu
adzakulipirani Malipiro abwino,
koma ngati Mutembenuka monga
mudatembenukira kale
Adzakulangani ndi chilango
chowawa.
17. Palibe tchimo pa wakhungu,
palibenso Tchimo pa olumala,
palibenso Tchimo pa wodwala
(atasiya kupita Kunkhondo). Ndipo
amene angamvere Mulungu ndi
Mtumiki Wake, Adzam'lowetsa
m'minda momwe Mukuyenda
mitsinje pansi pake; ndipo Amene
anyozere, amulanga ndi Chilango
chowawa.
18. Ndithu, Mulungu
adawayanja okhulupirira Pamene
amagwirana nawe chanza pansi Pa
mtengo pomwe amakulonjeza
(Kuti adzamenya nkhondo mpaka
imfa) Mulungu adadziwa zomwe
zidali M'mitima mwawo ndipo
adatsitsa pa Iwo kukhazikika (ndi
kudekha;) ndipo Adawalipira
kupambana kwapafupi.
19. Ndipo zotola zambiri
zapankhondo Adzazitenga; ndipo
Mulungu Ngwamphamvu zoposa,
Wanzeru Zakuya.
20. Mulungu wakulonjezani
zotola zambiri Zapankhondo
(zomwe) mudzazitenga, Ndipo
<&jRlg&2
Surat 48. Al-Fath Juzu 26
1110
tn *>»
t A gd\ 3 j^
wachita changu kukupatsani izi,
(Zinazo asanakupatseni). Ndipo
Watsekereza manja a anthu pa inu
(kuti Asakumenyeni). Ndi kuti
chikhale Chisonyezo cha
okhulupirira (amene Akudza
pambuyo panu), ndi kuti
Akuongolereni kunjira yolunjika.
21. Ndi zina zimene
simudazithe (Kuzipeza); Mulungu
Wazidziwa. Ndipo Mulungu
Ngokhoza chilichonse.
22. Amene sadakhulupirire
akadayesa Kumenyana nanu;
akadatembenuza Misana kuthawa;
kenako sakadapeza Mthandizi
kapena mtetezi.
23. Chimenecho ndicho
chizolowezi cha Mulungu chimene
chidapita kale, ndipo Sungapeze
kusintha pa chizolowezi Cha
Mulungu.
24. Ndipo lye ndi amene
adatsekereza Manja awo pa inu;
ndi manja Anu pa iwo, pa chigwa
cha Makka, atakupambanitsani pa
iwo. Ndipo Mulungu akuona zonse
Zimene mukuchita.
25. Iwowo ndiamene
sadakhulupirire, Ndipo
adakutsekerezani kulowa
Mu'Msikiti wopatulika pomwe
nyama Zansembe zidangomangika
osakafika Pamalo pake.
%&&£!&!&£&
^'Mfo
Surat 48. Al-Fath Juzu 26
1111
n *>•»
t A £SdM 6jj*i
Kukadakhala kuti kulibe Amuna
okhulupirira ndi akazi Okhulupirira
omwe simudawadziwe kuti
Mungawaponde potero inu
Nkudzudzulidwa popanda
kudziwa, (Mulungu akadakulolezani
kumenyana Nawo. Koma wachita
izi) kuti iye Amulowetse ku
mtendere Wake amene Wamfuna.
Akadadzipatula, Tikadawalanga
ndi chilango chowawa, Amene
sadakhulupirire pakati pawo.
26. Pamene omwe
sadakhulupirire adaika Mkwiyo
m'mitima, mkwiyo waumbuli,
Mulungu adatsitsa chikhazikiko
Chake Ndi kudekha pa Mtumiki
Wake ndi pa Okhulupirira, ndipo
adawalimbikitsa ndi Mawu woopa
Mulungu; ndipo adali eni Mawuwo
ndi oyenerana nawo. Ndipo
Mulungu Ngodziwa chilichonse.
27. Ndithu, Mulungu
adamtsimikizira Mtumiki Wake za
maloto ake oona: "Ndithu, inu
mudzalowa muMsikiti Wopatulika
mwamtendere, Mulungu Akafuna;
mudzameta mitu ndi kuyepula
Tsitsi lanu, simudzaopa (nthawi
Imeneyo); ndipo Mulungu
amadziwa Zimene simumazidziwa,
ndipo Zisanapezeke zimenezo,
akupatsani Kupambana kumene
kuli pafupi.
9?
Surat 48. Al-Fath Juzu 26
1112
y-\ fr>i
£ A jjaiJi 5jj-»
28. lye ndiYemwe adatumiza
Mtumiki Wake Ndi chiongoko ndi
chipembedzo choona Kuti achiike
pamwamba pa zipembedzo Zonse.
Ndipo Mulungu akukwanira
Kukhala mboni (Yake).
29. Muhammad(SAW) ndi
Mtumiki wa Mulungu; Ndipo
amene ali pamodzi ndi iye
Ngamphamvu kwa osakhulupirira
(Mulungu), koma ngachifundo
chambiri Pakati pawo. Uwaona
akugwira M'maondo ndi kugwetsa
nkhope zawo Pansi ncholinga
chofuna zabwino za Mulungu ndi
chikondi (Chake). Zizindikiro
zawo zili pankhope zawo
Zosonyeza kulambira kwawo. Hi
ndi Fanizo lawo m'Chipangano
chakale, Ndipo fanizo lawo
m'Chipangano Chatsopano nkuti
iwo ali monga mmera Womwe
watulutsa nthambi zake; Kenako
(nthambizo) nkuulimbitsa ndi
Kukhala waukulu ndi kuima
Bwinobwino ndi tsinde lake,
Nkuwasangalatsa omwe
adaubzala. (Choncho) zotsatira
zake, Nkuwakwiyitsa
osakhulupirira chifukwa Cha iwo.
Mulungu walonjeza Chikhululuko
ndi malipiro aakulu (kwa) Amene
akhulupirira ndi Kuchita zabwino
mwa iwo.
Surat 49. AI-Hujurat Juzu 26 I 1113 I t n *j*-i £ ^ ot^jJ-i Sj^
Surayi yayamba ndi kuletsa okhulupirira kupititsa lamulo
pachinthu, Mulungu ndi Mthenga Wake asanalamule, ndi
kukweza mawu awo pamwamba pa mawu a Mtumiki (madalitso
ndi mtendere zikhale naye). Ndipo yatama amene amatsitsa
mawu awo akakhala ndi Mtumiki (madalitso ndi mtendere
zikhale naye), ndi kudzudzula amene asiya miyambo yabwino
pomaitana Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) uku
ali kuseri kwa zipinda za nyumba ya Mtumiki (madalitso ndi
mtendere zikhale naye).
Kenako yalamula Asilamu kuti azikhazikika mitima ndi
nkhani za anthu achinyengo, ofooka pa chikhulupiriro. Ndipo
yalamula aweruzi zimene angachite ndi magulu awiri a Asilamu
akamenyana. Ndipo yaletsa Asilamu kuchitirana chipongwe
pakati pawo kusambulana, ndi kuwaganizira zoipa anthu
abwino, ndi kufufuza zolakwa zawo. Arabu a m'madera a
m'chipululu yawaletsa kudzitama ndi chikhulupiriro pomwe
chisadakhazikike m'mitima mwawo.
Kenako Surayi yafotokoza za okhulupirira amene ali oona
pachikhulupiriro. Ndipo yamaliza ndi nkhani yoletsa kumkumba
Mtumiki wa Mulungu (madalitso ndi mtendere zikhale naye),
chifukwa cholowa kwawo m'Chisilamu. Ndipo yafotokoza kuti
Mulungu ndiye woyenera kuwakumba pa zabwino zimene
wawachitira iwo powaongolera ku chikhulupiriro.
Surat 49. Al-Hujurat Juzu 26 1114 Y 1 *jfci £ * oiyjJ-i 5^
Sam* Al-Hujurat XLIX
-^ ■■^•v^>;
0»^j
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. E, inu amene mwakhulupirira!
Musamatsogoze (kulamula chinthu
Chapachipembedzo kapena
cham'dziko) Patsogolo pa (mawu
a) Mulungu ndi Mthenga Wake.
Ndipo muopeni Mulungu, Ndithu
Mulungu Ngwakumva Ngodziwa.
2. E, inu amene
mwakhulupirira! Musamakweze
mawu anu pamwamba Pa mawu a
Mneneri; musakweze mawu
Pokamba naye monga momwe
Mumayankhulira nokhanokha,
kuopa Kuti zochita zanu
zingaonongeke (ndi Kukhala
zopanda mphoto) pomwe inu
Simukuzindikira.
3. Ndithu, amene akutsitsa
mawu awo Pamaso pa mtumiki wa
Mulungu, iwo Ndiamene Mulungu
wawayeretsa Mitima yawo
pomuopa lye; Chikhululuko ndi
malipiro akulu Zidzakhala pa iwo.
4. Ndithu, amene akukuitana
(uku ali) Kuseri kwa zipinda (za
nyumba), ambiri A iwo sazindikira.
5. Ndipo iwo akadapirira ndi
kuyembekeza (Kuti) mpaka
utuluke ndi kudza kwa iwo,
oj*&\vP&\fr\j*
Jb
Siirat 49. Al-Hujurat Juzu 26
1115
Yt ft>»
t ^ Olj^-l Ojj-*»
Zikadakhala zabwino kwa iwo;
koma Mulungu Ngokhululuka
kwabasi Ngwachisoni.
6. E, inu amene mwakhulupirira!
Ngati Atakudzerani munthu
wosakhulupirika Ndi nkhani
(iliyonse, musamuvomereze);
Ifufuzeni (kaye) kuopa kuti
mungachitire Anthu (mtopola)
mwaumbuli, ndikuti
Mungazanong'oneze bondo pa
zomwe Mwachita.
7. Ndipo dziwani kuti mwa inu
muli Mtumiki wa Mulungu,
(mumvereni iye Zimene
akukuuzani) kukadakhala kuti Iye
akukumverani pa zinthu zambiri
(Zimene mukumuuza),
mukadavutika. Koma Mulungu
wachichita Chikhulupiriro kukhala
chokondedwa Kwa inu ndipo
wachikometsa M'mitima mwanu
ndipo wakuchitani Kuti mukude
kusakhulupirira ndi Ufasiki
(kutuluka m'malamulo a Mulungu)
ndi kunyoza (Mulungu.) Iwowo
ndiwo oongoka.
8. (Chifukwa cha) ubwino
wochokera kwa Mulungu ndi
mtendere (Wake, mwapeza
Zimenezi); ndipo Mulungu
Ngodziwa Ngwanzeru zakuya.
9. Ndipo ngati magulu awiri
aokhulupirira Atamenyana
ayanjanitseni pakati pawo. Ngati
m*
^■^'^ozmi
<$&&&?<£&&&$&
Siirat 49. Al-Hujurat Juzu 26
1116
Tl *>i
t ^ Olj^-l Sjj~-
gulu limodzi mwa magulu awiriwo
Likuchitira mtopola linalo,
limenyeni Limene likuchita
mtopola mpaka Libwerere ku
lamulo la Mulungu; Ngati
litabwerera, ayanjanitseni pakati
Pawo mwachilungamo, ndipo
chitani Chilungamo; ndithu,
Mulungu amakonda Ochita
chilungamo.
10. Ndithu, okhulupirira onse
ndi pachibale Choncho
yanjanitsani pakati pa abale Anu;
(musanyozere lamulo la
Kuyanjanitsa) ndipo muopeni
Mulungu Kuti akuchitireni
chifundo.
11. E, inuamene
mwakhulupirira! Amuna Asanyoze
amuna anzawo; mwina
(Onyozedwa) nkukhala abwino
(kwa Mulungu) kuposa iwo
(onyoza). Nawonso akazi asanyoze
akazi anzawo; Mwina onyozedwa
nkukhala abwino (Kwa Mulungu)
kuposa iwo (onyoza). Ndipo
musatukwanizane pokumbana
Mitundu kapena kuitanana ndi
maina Oipa. Taonani kuipa
kumuyitanira Munthu ndi dzina
loti fasiki (wotuluka M'malamulo
a Mulungu.) Atakhulupirira kale;
ndipo amene salapa (ku zimenezi),
iwo ndiwo (ochimwa) Odzichitira
okha chinyengo .
*$ ,-fe;,<v v 1,^\ '*.-fit*SK
Surat 49. Al-Hujurat Juzu 26 | 1117 | n *>i H oiy^i 0^
12. E, inu amene
mwakhulupirira! Dzipatuleni
kwambiri kuwaganizira Zoipa
(anthu abwino). Ndithu,
Kuganizira (anthu) maganizo
(oipa) Nditchimo. Ndipo
musafufuzefufuze (Nkhani za
anthu) ndiponso musajedane
Pakati panu. Kodi m'modzi wa inu
Angakonde kudya minofu ya
m'bale Wake wakufa?
Simungakonde zimenezo
Ndipo muopeni Mulungu. Ndithu,
Mulungu Ngolandira kulapa,
Ngwachisoni.
13. E, inu anthu! Tidakulengani
(nonse) Kuchokera kwa mwamuna
(m'modzi; Adamu) ndi mkazi
(m'modzi; Hawa), Ndipo
tidakuchitani kukhala a Mitundu
ndi mafuko (Osiyanasiyana) kuti
m'dziwane (basi). Ndithu,
wolemekezeka kwambiri mwa Inu
kwa Mulungu, ndi yemwe ali
woopa. Ndithu Mulungu
Ngodziwa, ndipo Ngodziwa
kwambiri nkhani zonse.
14. Anthu okhala m'zipululu
adanena(kuti): "Takhulupirira".
Nena, Simudakhulupirire
(kwenikweni); komaNenani
(kuti): "Tagonjera (Mulungu)"
Ndipo mpaka pano chikhulupiriro
Sichidalowe m'mitima mwanu
(ndi Kukhazikika bwinobwino).
Siirat 49. Al-Hujurat Juzu 26 ms tu>i £ * oiy-uM Sj^
Koma ngati Mumvera Mulungu
ndi Mtumiki Wake,
Sakuchepetserani chilichonse
m'zochita Zanu. Ndithu, Mulungu
Ngokhululuka Kwabasi,
Ngwachifundo chambiri.
15. Ndithu, amene ali
okhulupirira (moona) Ndiomwe
akhulupirira Mulungu ndi Mtumiki
Wake, ndipo kenako nkukhala
Osakaika, nkuchita nkhondo panjira
ya Mulungu, ndi chuma chawo,
ndi matupi awo, Iwowo ndiwo
oona (pa chikhulupiriro Chawo).
16. Nena: "Kodi
mukumdziwitsa Mulungu Za
chipembedzo chanu? Koma
Chiklialirecho Mulungu akudziwa
zonse Za kumwamba ndi za
m'dziko lapansi. Ndipo Mulungu
Ngodziwa chilichonse.
17. Akukukumba iwe chifukwa
cha kulowa Kwawo m'Chisilamu
(ngati kuti Akuchitira ufulu).
Nena: "Kulowa Kwanu
m'Chisilamu musakuyese Kuti
mwandichitira ubwino ine, koma
Mulungu ndiAmene wakuchitirani
ubwino Pokuongolerani ku
chikhulupiriro, ngati Muli oona.
18. Ndithu, Mulungu akudziwa
zobisika za Kumwamba ndi
zamnthaka. Ndipo Mulungu
akuona zimene mukuchita.
®i
4.>ij
^^*r^tJS»#
0^
Siirat 50. Qaf
Juzu 26
1119 "*>i
o • Jj OjJ-**
Surayi, kumayambiriro kwake, ikufotokoza za kutsimikiza
kwa uthenga wa Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye)
ndi kutsutsa kwa osakhulupirira zakudza kwa Mthenga
wochokera mwa iwo, ndi kusakhulupirira zakuuka ku imfa
atasanduka fumbi. Ndipo yasonyeza zizindikiro za chilengedwe
cha dziko lapansi ndi kumwamba zomwe zikulangiza kuti
Mulungu sangalephere kuukitsa anthu ku imfa.
lye ndi Amene adawalenga pomwe poyamba sadali kanthu.
Ndipo akudziwa zomwe mitima yawo ikuwanong'oneza ndi
kulemba zochita ndi zonena zawo m'kaundula wosungidwa
bwino. Ndipo yanenetsa Surayi kuti kuyesayesa kwa
osakhulupirira pa tsiku lachiweruzo kupereka madandaulo kwa
Mulungu kuti Satana ndi amene adawasokeretsa,
sikudzawapindulira kanthu. M'malo mwake, Satana pamodzi
ndi iwo adzaponyedwa ku moto. Ndipo pamenepo Mulungu
adzachitira okhulupirira ubwino powalowetsa ku Munda wa
mtendere wamuyaya.
Kenako Surayi yamaliza nkhani yake ndi kulamula Mtumiki
kuti apirire ku mazunzo a osakhulupirira omwe salingalira
zimene zidawagwera anthu amibadwo yoyamba. Ndipo
yamulangiza kuti alimbe pa mapemphero a Mulungu, nkutinso
iye ntchito yake ndi kukumbutsa okhulupirira, osati kukakamiza
osakhulupirira kuti akhulupirire.
Surat 50. Qaf
Juzu26 1120 tn*j*-i
% Jj 5jJ-*»
Swraf ga/ L
* : # : ;; : ,:. i^ii>^ .<^\#
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Qdf: Ndikulumbira Qur'an
yolemekezekayi (Ndithu,
mudzaukitsidwa ku imfa).
2. Koma akudabwa chifukwa
chowadzera Mchenjezi wochokera
mwa iwo. Ndipo osakhulupirira
adanena: "Ichi nchinthu
chodabwitsa."
3. Kodi tikadzafa ndi kukhala
fumbi (Tidzaukanso?) Kubwerera
kumeneko Nkwakutali kwambiri,
(Nkosatheka)"
4. Ndithu, tikudziwa chimene
nthaka Ikuchepetsa m'matupi
mwawo (Akalowa m'manda).
Ndipo kwa Ife kuli Kaundula
wosungidwa.
5. Koma adatsutsa choona
pamene Chidawadzera. Ndipo iwo
ali m'chinthu Chosokonezeka.
6. Kodi sawona thambo
pamwamba pawo M'mene
tidalimangira ndi Kulikongoletsa?
Ndipo lilibe ming'alu.
7. Ndipo nthaka tidaiyala; Ndi
kuika mapiri m'menemo Ndi
kumeretsamo m'mera Wokongola
wamtundu uliwonse.
o^JJl^^U-
-2>
^^M^M'm^
*• * H *
*&$&&&&&&
©,
Surat 50. Qaf
Juzu26 1121 tl*j*-i
o • <3 ^jj- -
8. (Kuti zimenezi zikhale)
chotsekula Maso ndi chikumbutso
kwa munthu Aliyense
wotembenukira (Kwa Mulungu).
9. Ndipo tatsitsa madzi
odalitsidwa Kuchokera
kumitambo, ndipo Kupyolera
m' madzi wo, tameretsa (Mmera)
m'minda ndi mbewu Zokololedwa;
10. Ndi mitengo italiitali ya
kanjedza Yokhala ndi mikoko
yazipatso Zothonana,
11. (Kuti chikhale) chakudya
cha akapolo (a Mulungu); ndi
madziwo taukitsa dziko Lakufa
(louma). Momwemo ndimmene
Kudzakhalira kutuluka m'manda
(Muli moyo).
12. Kale, iwo kulibe, adatsutsa
anthu A Nuhi ndi eni chitsime ndi
Asamudu.
13. Ndi Adi, ndi Farawo ndi
Abale a Luti,
14. Ndi anthu a m' mitengo (ya
Aika), ndi Anthu a Tubba; onsewo
adatsutsa Aneneri; choncho chenjezo
Langa Lidatsimikizika (pa iwo).
15. Kodi tidatopa nkulenga
Koyamba? Koma iwo ali
M'maganizo osokonezeka
M'zakalengedwe katsopano.
16. Ndithu tidamulenga
munthu, ndipo Ife Tikudziwa
<7) 9 A 9' *&\ \\.£t' 9 C
£$m^^y&
9] 9\'?\' ?>'J*&\"
Surat 50. Qaf
Juzu26 1122 *^ *>*
o • (3 ^jj-* 1
zimene mtima wake
Ukumunong'oneza; ndipo Ife tili
pafupi Ndi iye kuposa mtsempha
wam'khosi Mwake.
17. Pamene amalandira olandira
Awiri (Angelo), wina amakhala
kudzanja Lamanja, wina kudzanja
lamanzere,
18. Palibe chilichonse chimene
Amayankhula koma pafupi ndi iye
pali Mlonda amene wakonzekera
(kulemba).
19. Ndipo kuledzera kwa imfa
kukam'dzera Mwa choona,
(pamenepo adzauzidwa): "Ichi ndi
chomwe mumachithawa chija."
20. Ndipo lipenga
lidzaimbidwa; limenelo Ndilo
tsiku lamavuto (tsiku
Lachiweruziro).
21. Ndipo udzadza mzimu
uliwonse Pamodzi ndi m'busa
(wake) ndi mboni (Yake).
22. (Adzauzidwa): "Ndithu,
udali Wosalabadira zinthu izi; basi
Takuvundukulira (chomwe)
Chimakuphimba, ndipo
kuyang'ana Kwako lero
nkwakuthwa!"
23. Ndipo (Mngelo) yemwe
adali naye (Pamodzi
ndikumalemba zochita zake)
Adzanena (kwa Mngelo
%&&v^&&&®
-• >^ w x
,*i»t^» .«: jr.tvli . t».f » - fc*i
«QK3Mu8y%*»
® uu£*6u&lai '<&%$b
Surat 50. Qaf
Juzu26 H23 m »>■!
• (3 5jj-u
wachilango): "Izi ndizimene
zidakonzedwa ndi ine.
24. Mponyeni kumoto Aliyense
amene Wokanira wamakani.
25. Wotsekereza zabwino,
Wolumpha Malire, wokaika;
26. Amene adadzipangira
milungu ina ndi Kumphatikiza ndi
Mulungu. Mponyeni kuchilango
chaukali".
27. Mnzake(satana) adzanena:
"O, Mbuye Wathu!
Sindidamsokeretse, Koma iye
mwini Adali wosokera kutali
kwambiri ndi Choonadi".
28. (Mulungu) adzanena:
"Musakangane kwa Ine;
ndidakutsogozerani kale chenjezo
(Langa)"
29. Mawu Anga sasinthidwa
kwa Ine, ndipo Ine siwopondereza
Akapolo (Anga).
30. Tsiku limene tidzaifunsa
Jahannama: "Kodi wadzaza?" Iyo
idzanena: "Kodi kuli Zoonjezera?"
31. Ndipo munda wa mtendere
Udzayandikitsidwa pafupi kwa
oopa (Mulungu).
32. "Izi ndizimene
mumalonjezedwa, za Aliyense
wotembenukira Kwa Mulungu,
Wosunga (malamulo Ake).
#4?$«a$
Surat 50. Qaf
Juzu26 1124 TWjA-i
o * <j <*jj-»»
33. Amene adaopa (Mulungu),
Wachifundo Chambiri, pomwe
samamuona ndi maso, Ndipo
adadza ndi mtima wotembenukira
(Kwa lye)."
34. (Adzauzidwa): "Uloweni
Mwamtendere"; limeneli ndi tsiku
Lokhazikika mpaka muyaya
35. M'menemo adzapeza
chilichonse (Chimene) adzafune,
ndipo kwa Ife kuli Zoonjezera.
36. Ndipo kodi ndi mibadwo
Ingati tidainonga Kale iwo kulibe,
yamphamvu kuposa Iwo?
Adayendayenda padziko.Kodi
Padalipo pothawira?
37. Ndithu, m'zimenezi muli
chikumbutso Kwa yemwe ali ndi
mtima ndi yemwe Akutcherera
khutu (uku) iye ali pompo (Ndi
maganizo ake).
38. Ndithu, tidalenga thambo
ndi nthaka ndi Zapakati pake
m'masiku asanu ndi Limodzi, ndipo
sikudatikhuze kutopa Kuli konse.
39. Choncho, pirira nazo
zomwe akunenazo, Ndipo
lemekeza Mbuye wako
Pomutamanda dzuwa lisadatuluke,
(Swala ya Subuhi), ndi (dzuwa)
Lisadalowe, (Swala ya Asiri),
40. Ndi gawo lausiku, (swala ya
Magharibi Ndi Ishaa); ndiponso
© ^!3^W#^
<^j©8£$$&»
®>3PW&%$$te
Surat 50. Qaf
Juzu 26
1125
y\ *>i
* (j ^JJ - "**
(mulemekeze) pambuyo Pa
mapemphero (popemphera Swala
Za Sunna, monga Surma za
kabuliya ndi Baadiya ndi Tahajudi).
41. Ndipo mvetsera (za) tsiku
limene Woitana adzaitana
kuchokera pamalo Apafupi.
42. Tsiku limene adzamva
phokoso mwa Choonadi: limenelo
ndilo tsiku Lodzatuluka (m'manda).
43. Ndithu, Ife ndi amene
timapereka moyo Ndi kupereka
imfa; ndipo kobwerera Nkwathu,
44. (Akumbutse za) tsiku
limene nthaka Idzang'ambike kwa
iwo Mwachangu; kusonkhanitsa
kumeneko Nkosavuta kwa Ife.
45. Ife tikudziwa bwino zimene
akunena; iwe Suli
wowakakamiza. Choncho
mukumbutse Ndi Qur'an yemwe
akuopa chilango Changa.
Surat 51. Adh-Dhariyat Juzu 26
1126
t n *j*-1 O ) OUjlJUt dj^
Surayi yayamba ndi kulumbira kwakuti: Ndithu, kuuka ku
imfa ndi chiweruzo zilipo popanda chikaiko. Ndipo yatsatizanso
kulumbira kwina pa zakutsutsana kwa okana Chisilamu
pazimene akumunenera Mneneri wa Mulungu, Muhammad
(SAW), ndi Qur'an kuti mawu awo ngonama.
Kenako ikuchenjeza okanawo kuipa kwa malo awo obwerera
ndi kupereka chithunzi cha zomwe oopa Chauta awakonzera
monga mphoto ya ntchito zabwino zimene adatsogoza akadali
padziko lapansi. Ndipo kenaka yatiuza kuti tiganizire
zazizindikiro za Mulungu m'dziko ndi m'moyo wathu, ndi
zolengedwa zodabwitsa zimene zidaikidwa m'menemo, zosalala
m'kalengedwe.
Surayi yafotokozanso nkhani ya Ibrahim pamodzi ndi alendo
ake angelo. Ndipo yasonyeza chikhalidwe cha mibadwo ina ndi
chionongeko chimene chidawapeza chifukwa chakutsutsa
aneneri awo. Kenako yasonyeza mwachidule zina mwa
zizindikiro za Mulungu m'dziko ndi kulimbikitsa anthu kuti
abwerere kwa Chauta ndi kuti mapemphero akhale a Mulungu
yekha. Ndipo mapemphero ndicho cholinga cholengedwera
ziwanda (majini) ndi anthu.
Surayi yamaliza ndi kuchenjeza otsutsa Mneneri wa Chauta
za chilango chonga chimene idachilandira mibadwo yakale.
Surat 51. Adh-Dhariyat Juzu 26 1 1127 I T n ^jA-i o > objiJJi oj^
5wra/ Adh-Dhariyat LI
: M^T&^
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Ndikulumbirira mphepo
imene Ikubalalitsa Mitambo ya
mvula;
2. Ndi imene imasenza mitolo
Yolemera (ya madzi).
3. Ndi kuyenda (nawo
madziwo) Mwaubwino;
4. Ndi awo amene amagawa
riziki (limene Mulungu amalipereka
kwa amene Wamfuna).
5. Ndithu, zimene
mukulonjezedwa Nzoonadi,
(zidzachitika);
6. Ndipo, ndithu,malipiro (pa
Zochita zanu) adzapezekadi.
7. Ndikulumbirira thambo la njira
Zake zambiri zoikidwa mwaluso,
8. Ndithu, inu muli m'mau
otsutsana, (Pazimene mukunena)
9. (Kupyolera m'mawu
amenewa) Akuchotsedwa ku icho
(chikhulupiriro Chalonjezo loona)
amene Adachotsedwa (ku
chikhulupirirocho).
10. Aonongeka abodza (amene
akunena Za tsiku lachiweruzo
mongoganizira.)
o^f^jll^l*.
^4M
v y^
&&&&
SuratSl. Adh-Dhariyat Juzu26| H28 I T1 *>-» o\ objiiii *^
11. Iwo amene akubira
muumbuli, Osalabadira (za tsiku
lomaliza).
12. Akufunsa (mwachipongwe
ponena kuti) "Lidzakhala liti tsiku
lamalipiro?"
13. (Limenelo ndi) tsiku lomwe
iwo Adzalangidwa kumoto.
14. (Adzawauza kuti): "Lawani
chilango Chanu ichi chimene
Munkachifulumizitsa (kuti
chikufikeni).
15. Ndithu, oopa (Mulungu)
adzakhala (Akusangalala)
m'minda ndi Mu akasupe
okongola,
16. Uku akulandira zimene
wawapatsa Mbuye wawo (malipiro
aulemu); Ndithu, iwo amachita
zabwino Asanapeze izi.
17. Nthawi yausiku amagona
pang'ono, (Amadzuka nachita
mapemphero Mochulukitsa),
18. Ndipo kum'bandakucha,
iwo Amapempha chikhululuko,
19. Ndipo m'chuma Chawo
mudali gawo (Lodziwika) la
opempha Ndi osapempha (mwa
osauka).
20. M'nthaka muli zizindikiro
kwa Otsimikiza, (Zosonyeza kuti
Mulungu alipo).
£$ay£a*g#
yiMS3f-'>*<
®v&Mfr$i.
SOj
*&&&$&&&
<e SB*SV - w11 '"
&
Surat 51. Adh-Dhariyat Juzu 26 1 129 n * >» * i ob iJUi 5^
21. Ndi mwa inu nomwe; Kodi
simuona?
22. Ndipo kumwamba kuli
Zokuthandizani (pa moyo wanu),
ndi Zimene mukulonjezedwa.
23. Ndikulumbirira Mbuye wa
kumwamba Ndi pansi,
ndithu,zimenezo ndi zoona
Monga kulili Kuyankhula kwanu.
24. Kodi yakufika nkhani ya
alendo a Ibrahim; (angelo)
Olemekezeka?
25. Pamene adalowa kwa iye
ndi Kunenakuti: "Salaam",
("Mtendere")! Iye
Adayankha:"Salaam" ("Mtendere)
inu Ndinu anthu osadziwika
(achilendo)".
26. Adatembenukira kwa
akunyumba ake
(Mwakachetechete), ndipo adadza
Ndi nyama ya mwana wa ng'ombe
Yonona (yowotcha).
27. Naipereka kwa iwo (koma
sadadye); Iye adanena (modabwa):
"Kodi bwanji Simukudya?"
28. Mumtima mwake
adadzazidwa manthaNdi iwo. Iwo
adati: "Usaope," Ndipo adamuuza
nkhani yabwino Ya kubala mwana
wodziwa.
29. Adadza mkazi wake ndi
mkuwe (Pamene adamva nkhani
&,,&
i*M*fc$to&
Surat 51. Adh-Dhariyat Juzu 27 1 130 TV * j*-i \ oUjiJUi 5 ^
yabwino ija). Adadzimenya
kunkhope (ndi dzanja lake
Kusonyeza kudabwa ndi
kusatheka). Ndipo Adati: ("Ine
ndine) nkhalamba (Ndiponso)
chumba; (ndingabereke Bwanji)?"
30. Iwo adati: "Momwemo,
Mbuye wako wanena. lye
Ngwanzeru Zakuya (pa
chilichonse chimene Akulamula);
Ngodziwa; (palibe Chimene
chingabisike kwa lye).
31. (Ibrahim) adati: "Kodi
mwadzanso Nchiyani? E, inu
otumidwa!"
32. Iwo adati: "Tatumizidwa
kwa Anthu oipa .
33. Kuti tiwagende ndi miyala
Yotenthedwa Kuchokera kudongo.
34. Yoikidwa chizindikiro cha
Aliyense wochimwa kuchokera
kwa Mbuye wako."
35. Okhulupirira omwe adali
m'mudzimo, tidalamula kuti
atuluke.
36. Sitidapeze mmenemo
(okhulupirira Ambiri) kupatula
mnyumba imodzi Ya Asilamu.
37. Ndipo tidasiya pamenepo
Chizindikiro (chosonyeza
kuonongeka kwa eni mudziwo kuti
chikhale lingaliro) Kwa amene
akuopa chilango Chopweteka.
^\^4ysv^
©
Surat 51. Adh-Dhariyat Juzu 27 1 1131 I TVt>i \ oUjiJUi 9JJ *
38. M'nkhani ya Musa (muli
phunziro) Pamene tidamtuma kwa
Farawo uku Atalimbikitsidwa ndi
chisonyezo Choonekera.
39. Koma Farawo adanyoza
(kukhulupirira Musa) chifukwa
chotama nyonga zake, Ndipo adati:
"Uyu ndi wamatsenga kapena
Wamisala".
40. Tidamlanga pamodzi ndi
khamu lake La nkhondo ndi
kuwaponya mnyanja; iye ali
Wodzudzulidwa.
41. Ndipo m'nkhani ya Adi
(muli phunziro) Pamene
tidawatumizira chimphepo
(Chamkuntho) chopanda chabwino
mkati Mwake.
42. Chomwe sichisiya chinthu
chimene Chachidutsa koma
kuchichita monga Chofumbwa.
43. Ndipo m'nkhani ya Samudu
(Muli chisonyezo) pamene
Kudanenedwa kwa iwo kuti:
"Sangalalani (mnyumba zanu)
mpaka Nthawi yakutiyakuti."
44. Koma adadzikweza
(ponyozera) Lamulo la Mbuye
wawo. Choncho Chiphokoso
chidawaononga uku Akupenya.
45. Sadathe kuimirira ndi
(kuthawa) Ndiponso sadali
Wodzipulumutsa.
9 &
^»a5A»i^J3
^i^^f^A^^^h $*$>
k^i&&\\p&&z.
L 9 ™*
J*X 1 \\9 9 J* <"$< 9 *' 9\ 9'x9?
%&$&^jx®&
Surat 51. Adh-Dhariyat Juzu 27 1 \ 132 | Y V » j*-i 1 obji JUi Sjj-
46. Naonso anthu a Nuhi
(Tidawaononga) kale chifukwa
iwo Adali anthu otuluka
mchilamulo (cha Mulungu).
47. Thambo tidalimanga
mwamphamvu (ndi Luntha); ndipo
tingathe kuchita zochuluka
(Kuposa zimenezi.)
48. Ndipo nthaka tidaiyala;
Taonani kukonza bwino Ife amene
tidakonza nthaka!
49. Chinthu chilichonse
tachilenga Ziwiriziwiri kuti inu
mulingalire (Ndi kukhulupirira
mphamvu Zathu).
50. Thawirani kwa Mulungu.
Ine ndine Mchenjezi woonekera
kwa inu Wochokera kwa lye.
51. Ndipo musadzipangire
Mulungu wina Wompembedza ndi
kumuphatikiza ndi Mulungu. Ndithu,
ine ndine mchenjezi Woonekera
poyera kwa inu wochokera Kwa lye.
52. Momwemo (ndimo idalili
mibadwo Yakale pamodzi ndi
aneneri awo); Palibe Mthenga
amene adawadzera Anthu akale,
anthu akowa kulibe, Popanda
kumnena kuti: "Ndiwamatsenga
kapena wamisala."
53. Kodi adalangizana za
mawuwa Pakati pawo? Iyayi,
koma iwo Ndianthu opyola Malire.
®<&2$§3 ^*^yi4A^-^5
f %P&X$i&&
Surat 51. Adh-Dhariyat Juzu 27 1133 TV *>i o ^ ob>iJUi 0^
54. Choncho apatukire iwo
(amakani.) I we suli
wodzudzulidwa (pakuleka Kwawo
kuyankha kuitana).
55. Kumbutsa. Ndithu,
Kukumbutsa kumawathandiza
Okhulupirira.
56. Sindidalenge ziwanda
(majini) ndi Anthu koma kuti
Azindipembedza.
57. Sindifuna kwa iwo
chithandizo Ndiponso sindifuna
Kuti azindidyetsa.
58. Ndithu Mulungu ndi Amene
ali ndi udindo wopatsa anthu Ake
madalitso; lye ndi Mwini
mphamvu Zoposa; Wolimba,
(salaphera kanthu).
59. Ndithu, amene adzichitira
okha Chinyengo (pokana ndi
kutsutsa) Ali nalo gawo la
chilango monga Gawo la anzawo
(a mibadwo yakale); Choncho
asandifulumizitse (kutsitsa
Chilango nthawi yake isanafike)!
60. Kuonongeka kuli pa amene
atsutsa za Tsiku lawo limene
alonjezedwa.
y«sBj**E5
^fe»«^3MSJ6
*&^C!&$£®z
9f \gl
©SfJiiftldl&tf^s
fi 9& 9 \99<$ '9 m #*(9l9'<
Surat 52. At-Tiir Juzu 27
1134
rv*>i
oy jjiaJ' ^J***
SURAT AT-TUR LII
Surayi yayamba ndikulumbirira zinthu zisanu mwa
zolengedwa zikuluzikulu potsimikiza kuti chilango chiwapeza
otsutsa, ndi kufotokoza m'mene chidzawapezere pamodzinso
ndi mitundu yake, pa tsiku la chiweruzo ndi kuuka ku imfa.
Yafotokozanso za nkhani ya mtendere kwa oopa Mulungu ndi
zimene azikasangalala nazo mu minda yamtendere yamuyaya,
kudzanso mitundumitundu yaulemu umene azikalandira
kumeneko. Ndipo akawasangalatsanso powakumanitsa ndi ana
awo amene zochita zawo zabwino zidali zochepera poyerekeza
ndi zamakolowo.
Surayi yapitiriza ndi kulamula Mneneri (madalitso ndi
mtendere zikhale naye) kuti awasiye mpaka adzakumane ndi
tsiku limene adzaonongedwa. Ndipo yamulamula kuti apirire
ndi lamulo la Mbuye wake lolekerera osakhulupirirawo
osawalanga msanga, ndi kuti pazimenezi palibe vuto limene
lingampeze lye akumyang'anira ndi kumsunga. Ndipo
wauzidwanso kuti apitirize kulemekeza Chauta ndi kumpatula
ku makhalidwe osayenerana ndi makhalidwe ake, makamaka
nthawi yolowa nyenyezi.
Surat 52. At-Tiir Juzu 27 1135 rv»>i
1 jjlaJl i jj»-
Surat At-Tur LII
a ^ -?■-*■ ''"
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Ndikulumbirira phiri la Turi
(ku Sinai Pamene Musa
adalankhulana Ndi Mulungu).
2. Ndi Buku lolembedwa.
3. M'mipukutu yazikopa
zotambasuka (Zosavuta kuwerenga);
4. Ndi nyumba yopitako
kawirikawiri (Pochitamo
mapemphero).
5. Ndi thambo limene
latukulidwa (Popanda mzati);
6. Ndi nyanja yodzadza ndi
madzi.
7. Ndithu, chilango cha Mbuye
wako (Chimene wawalonjeza
nacho Osakhulupirira) chiwapeza
(Popanda chipeneko);
8. Palibe wochichotsa (pa iwo).
9. Pa tsikulo thambo
lidzagwedezeka; Kugwedezeka
kwamphamvu.
10. Ndipo mapiri adzachoka
m'malo Mwake (moonekera).
11. Kuonongeka koopsa pa
tsiku Limenelo kuzakhala pa
Otsutsa choonadi;
o^l^l^W-
— w
v # i&
QJM
Z0i$A
™ ^ - %4*&
t'li *1Li\
*>"\\ 9'\\'
%^&<
HP&&A
Surat 52. At-Tur Juzu 27
1136 tV*>i
Y J^^' ^Jj^
12. Iwo amene akungosewera
Mzinthu zopanda pake.
13. Tsiku limene
adzakankhidwira Mwamphamvu
ku Jahannama (kumoto Woopsa).
14. (Kudzanenedwa kwa iwo):
"Uwu ndi Moto uja umene mudali
kuutsutsa (Padziko lapansi)
15. Kodi awa ndi matsenga
Kapena inu simukuona?
16. Lowanimo, (mulawe
kupsereza Kwake) pirirani (ndi
mavuto ake) Kapena musapirire,
ndichimodzimodzi Kwa inu. Ndithu
mulipidwa pazimene Munkachita."
17. Ndithu oopa Mulungu
adzakhala M'minda yamtendere
(yotambasuka Yosasimbika
kukongola kwake) Ndi
chisangalalo chachikulu.
18. Uku akukondwerera zimene
wawapatsa Mbuye wawo ndi
kuwatchinjiriza ku Chilango
chamoto.
19. (Kudzanenedwa kwa iwo):
"Idyani (Chakudya chamtendere);
ndipo imwani Mosangalala
kukhala malipiro pazimene
Munkachita padziko lapansi.
20. Uku atakhala moyadzamira
pa Mipando yondandika bwino ndi
Kuyalidwa bwino; ndipo
Tidzawakwatitsa akazi Ophanuka
maso mokongola.
%#&*&#&*
^ZfZ^j&ft* S
®cfi^S?$»&$»
ojj^^bliuJ^^l
9>K
^$^&$$
*V.'''.'Va'-*1 *» >> 'li " (**
Surat 52. At-Tur Juzu 27
1137
YV*j*-i
OX jjlaJl ^JJ --
21. Ndipo amene akhulupirira
Ndipo ana awo nkuwatsatira Pa
chikhulupiriro tidzawakumanitsa
iwo Ndi ana awowo ndipo
sitikawachepetsera Kalikonse
m'mphoto za ntchito zawo;
Munthu aliyense adzakoledwa ndi
Zochita zake;
22. Ndipo tidzawaonjezera
Zipatso ndi nyama imene
Adzakhala akuilakalaka.
23. Azikalandirana m'menemo
(Mwachikondi wina ndi mnzake)
chikho Chodzazidwa ndi
zakumwa; Sipakakhala kwa iwo
zolankhula Zachabe ngakhale
zochita zamachimo.
24. Ndipo azikawazungulira
anyamata Owatumikira onga ngale
yosungidwa M'chigoba chake
(kukongola kwawo)
25. Azidzatembenukirana wina
ndi Mnzake uku akufunsana (za
kukula Kwa mtendere umene
adzakhala Nawo ndi kuti adaupeza
chotani).
26. Adzanena: "Ife tidali oopa
chilango Cha Mulungu pakati pa
maanja athu (Tisadalandire
mtendere wu).
27. Ndipo Mulungu watidalitsa
ndipo Watitchinjiriza ku chilango
chamoto:
(99 '
"&£%'fi'$hl&d$£
©,
,MVA
*&
®Q^%3&M$
©yj^cJ&LSjij^&IgS
Surat 52. At-Tur Juzu 27
1138
rv $.>i
y j^q}\ Ojj-*»
28. Ndithu, ife timampembedza
(Kalero padziko lapansi) ndithu
lye Yekha ndiye wabwino
Ngwachifundo."
29. Choncho, kumbutsa,iwe suli
mlosi Kapena wamisala
pamtendere wa Mbuye wako;
30. Kapena akukunena iwe kuti
ndiwe Mlakatuli,
tikumuyembekezera, Imfa impeze.
31. Nena (kwa iwo moopseza)
"Yembekezerani! Ndithu ine ndili
nanu Mwa mmodzi
woyembekezera."
32. Kapena nzeru zawo ndizo
Zikuwauza izi kapena iwo Ndi
anthu opyola malire.
33. Kodi akunena kuti:
"Wadzipekera
(Mtumiki{SAW}Qur'an)"? Iyayi,
koma Iwo sakukhulupirira.
34. Atabwera ndi nkhani
yofanana ndi iyo (Qur'an) ngati ali
oona m'kuyankhula Kwawo (koti
Mtumiki{SAW}wapeka Qur'an.)
35. Kapena adalengedwa
popanda Mlengi Kapena iwo
adadzilenga okha (Nchifukwa
sakuvomereza za Mlengi
Wopembedzedwayo?)
36. Kodi ndiwo adalenga thambo
Ndi nthaka? Koma satsimikiza
(Zoyenera kumchitira Mlengi)
Surat 52. At-Tur Juzu 27
1139
YV t>l
O Y jjiaJl 5j>w
37. Kodi nkhokwe (za zabwino)
za Mbuye wako zili ndi iwo
(kotero Kuti akuzigwiritsa ntchito
mmene Angafunire?) Kapena iwo
Ngopambana?
38. Nanga kodi ali nawo
makwerero (Amene akukwerera
kumwamba) Kotero kuti
akumvetsera zimene Mulungu
akulamula? Choncho, omvetsera
Awo abwere nawo umboni
owonekera (Osonyeza kuona
kwawo Pazimene akunenazi).
39. Kodi lye (Mulungu) ndiye
Ali ndi ana akazi ndipo inu muli
ndi ana Aamuna?
40. Kodi ukuwapempha malipiro
Alionse (pofikitsa uthenga);
Kotero kuti iwo akulemedwa ndi
Kulipira (uthengawu)?
41. Kodi iwo amadziwa zamseri
kotero Kuti iwo akumalemba
(Zimene afuna)?
42. Kapena akufuna kukuchitira
chiwembu (Ndikuononga uthenga
wako?) Koma Amene
sadakhulupirire ndiwo omwe
Chiwabwerere chiwembu (chawo.)
43. Kodi ali naye
wompembedza, osati Mulungu
(amene angawateteze ku Chilango
cha Mulungu)? Mulungu
Wapatukana ndi zimene
akumuphatikiza Nazo.
^Ij&'^&f
4^&&»&a&p
Hs&&$$&&
%W£^wmi)&
Surat 52. At-Tur Juzu 27
1140
YV tjJt-i
Ot jjkil 5jj-*>
44. Koma akaona gawo
lathambo Likugwa (kuti liwalange)
akunena (Mwamakani ndi
kunyada): "Uwu ndi Mtambo
umene wasonkhanitsa Madzi a
mvula."
45. Asiye; (usalabadire za iwo)
mpaka Pomwe adzakumana ndi
tsiku lawo Limene
adzaonongedwa,
46. Tsiku lomwe chiwembu
chawo Sichidzawathandiza
chilichonse; Ndipo iwo
sadzapulumutsidwa.
47. Ndipo ndithu, amene achita
Zosalungama ali nacho chilango;
Chosakhala chimenecho (chilango
Chimene akuonongedwa Nacho
padziko lapansi)! Koma Ambiri a
iwo sadziwa (zimenezi).
48. Ndipo pirira ndi lamulo la
Mbuye wako Ndithu, iwe ndiwe
wosungidwa ndi Kuyang'aniridwa
ndi Ife; ndipo Lemekeza ndi
kumyamika Mbuye Wako pamene
ukuimirira,
49. Ndipo m'gawo la usiku
Mlemekeze lye ndi nthawi yolowa
Nyenyezi'.
hf^O^^^*^ ££
Surat 53. An-Najm Juzu 27 I 1141 1 TV *£?\ or p*Jt Sjj-*
Kulumbira koyambirira kwa Surayi kukuonetsa poyera kwa
Mneneri (madalitso ndi mtendere zikhale naye) pazimene
akufotokoza m'nkhani ya chivumbulutso ndi uthenga umene
akulalikira wa chivumbulutsocho. Sadasokere ndi
chivumbulutsocho ndipo sadalakwe chilichonse, koma akunena
zoona pazimene akufotokoza paulendo wake wonka kumwamba
m'nkhani (ya Miraj). Maso ake sadasokonezeke pazomwe
adaziona ndipo sadapyole malire.
Kenako Surayi ikulongosola nkhani ya kufooka kwanzeru za
osakhulupirira namapembedza mafano omwe adadzipangira ndi
manja awo ndi kuwatcha okha maina, monga momwe adatchera
angelo kuti ndi akazi, ndi kutinso ndi ana aakazi a Chauta,
pomwe iwo adadzisankhira ana aamuna.
Ndipo popitirira Surayi ikulangiza Mtumiki (madalitso ndi
mtendere zikhale naye) kuti apatukane nawo ndi kumusiyira
Mulungu zochita zawo, Amene ndi Mwini kumwamba ndi
pansi; Mwini kulenga. Ndiponso ndi Amene adzalipira wochita
zoipa, zoipa zake; wochita zabwino, zabwino zake. lye
Ngodziwa kwambiri kusinthasintha kwa chilengedwe cha
munthu ndi chikhalidwe chake. Ndipo akuchenjeza amene
akukana kuweruzidwa ndi munthu aliyense pa zochita zake
monga momwe zidalongosolera zipembedzo zakale. Ndipo
kalata za Musa ndi Ibrahim zidafotokozanso zomwezo.
Surayi yamaliza ndi kunenetsa kuti Qur'an ndi mchenjezi
monga mo we adalili achenjezi akale amene adachenjeza
mibadwo yakale kuti iope tsiku lachiweruziro limene nthawi
yake ili pafupi, ndipo kumapeto kwake yapempha Asilamu kuti
amulambire Mulungu.
Surat 53. An-Najm Juzu 27 1142 TV *>i
Of *J!tJl Ijy*
Surat An-Najm LIII
n* v>
*:":;; mm
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Ndikulumbira nyenyezi
pamene Zikulowa.
2. Sadasokere m'bale wanu
(Mtumiki Panjira ya choonadi)
ndipo sadakhulupirire Zonama.
3. Ndipo sayankhula zofuna za
mtima wake.
4. Iyoyi (Qur'an imene
akuinena), sichina, Koma
ndichivumbulutso
Chovumbulutsidwa.
5. Adamphunzitsa
(chivumbulutsochi) (Jibril)
wanyonga zambiri,
6. Wanzeru zakuya; ndipo
adakhadzikika (M'maonekedwe
ake).
7. Ali m'chizimezime
kumwamba.
8. Kenako (Jibril)
adamuyandikira (Mtumiki {SAW})
ndikuonjezera Kumuyandikira,
9. (Kumuyandikira kwake)
kudali ngati (Mpata wa) nsonga
ziwiri za uta, kapena Kuyandikira
kuposa apo;
ofa$\<&$\&\j
Surat 53. An-Najm Juzu 27 1143 TV ^jJt-i
Or p*dl 5jj~>
10. (Choncho Jibril)
adavumbulutsira Kapolo Wake
(wa Mulungu) zimene
Adazivumbulutsa.
11. Sudaname mtima (wa
Mtumiki) Pazimene adaziona.
12. Kodi mukutsutsana naye
(Mthenga wa Mulungu) pazimene
adaziona
13. Ndipo ndithu, adamuona
(Jibril) M'kuona kachiwiri
mkaonekedwe kake.
14. Pa 'Sidiratil Muntaha'
(mtengo Wamasawu pothera
zinthu zonse).
15. Pafupi pake pali Janatu
Ma'awa, (munda wokhalamo)
16. Pomwe chophimba
chidaphimba Msawuwo.
17. Maso ake sadaphonye
Kapena kupyola malire (oikidwa)
18. Ndithu, (Mneneri
Muhammad{SAW}) adaona zina
mwa Zizindikiro zikuluzikulu za
Mbuye wake (Zosonyeza
mphamvu Zake)
19. Kodi mwawaona Lata ndi
Uzza.
20. Ndi Manata; fano (lanu) lina
Lachitatu, (kuti iwowa ndi
milungu)?
© j^C'jj^^X'
^^t*#oaJ
&$&&%$
©o^^ys
Surat 53. An-Najm Juzu 27
1144
YVfrjA-i
Of a^cJl ^J-**
21. Kodi mwadzisankhira ana
Achimuna (kukhala anu), ndi
achikazi Nkukhala a lye (Mulungu)?
22. Choncho kugawa kumeneko
nkopanda Chilungamo (pompatsa
Mulungu zimene Mumazida).
23. Sali (mafanowo)
chilichonse koma ndi Maina basi
omwe mudawatcha inu ndi Makolo
anu, (molingana ndi zilakolako
zanu zachabe); Mulungu sadatsitse
Umboni pazimenezo (wotsimikiza
Pamawu anuwo). Sakutsatira koma
Zoganizira basi ndi zimene
Ikufuna mitima (yawo yopotoka).
Ndithu, chidawadzera chiongoko
Kuchokera kwa Mbuye wawo
(chomwe M'kati mwake mudali
kuongoka Kwawo akadachitsatira).
24. Kodi munthu akuganiza kuti
Adzapeza chilichonse chimene
Akuchilakalaka?
25. Tsiku lomaliza Ndi dziko
lapansi nza Mulungu yekha.
26. Ndipo kuli Angelo ambiri
kumwamba Omwe kuchonderera
kwawo sikungathandize China
chilichonse pokhapokha Mulungu
Ataloleza kwa amene Wamfuna
ndi kumuyanja
27. Ndithu, amene sakhulupirira
za (Moyo wa) tsiku lomaliza,
amatcha Angelo kuti ndiakazi;
Surat 53. An-Najm Juzu 27
1145
rv ftj*-i
OT ^cJl 5jj-j
28. Ndipo alibe kudziwa
kulikonse pa zimenezo Sakutsata
china koma maganizo ndithu,
Kuganizira sikuthandiza
chilichonse Pofuna kupeza
choonadi.
29. Choncho apewe
(osakhulupirirawa) Amene
anyozera Qur'an Yathu; ndipo
palibe Chimene akufuna koma
Umoyo wa padziko lapansi basi.
30. Zimenezo ndiwo mapeto A
kudziwa kwawo. Ndithu, Mbuye
Wako Ngodziwa kwambiri za
amene Akusokera njira Yake
Ndiponso akudziwa bwino za
yemwe Wawongoka.
31. Ndipo zonse za kumwamba
ndi zadziko Lapansi nza Mulungu
Yekha, (Pozilenga ndi
kuziyang'anira), Kuti adzawalipire
amene adaipitsa pazimene
Adachita ndi kutinso adzawalipire
zabwino Amene adachita zabwino.
32. Amene akuwapewa
machimo Akuluakulu ndi zadama,
kupatula Timachimo
tating'onoting'ono (timene
Mulungu amatikhululuka); ndithu,
Mbuye wako ndiwokhululuka
Kwakukulu.Iye akudziwa
chikhalidwe Chanu kuyambira
pomwe adakulengani Kuchokera
m'nthaka ndi pamene inu Mudali
©(JOCftl
Surat 53. An-Najm Juzu 27 I 1146 1 *V *j*-'
or j^idi-Sjj-.
makanda m'mimba mwa amayi
Anu (mosinthasintha;
mosiyanasiyana). Choncho
musadzitame nokha kuyera
Mtima; lye adziwa kwambiri za
yemwe Akuopa (Mulungu).
33. Kodi wamuona yemwe
wadzipatula (Pakusiya kutsatira
choonadi)?
34. Ndipo wapereka (chuma)
chochepa Nasiyanso kuperekako.
35. Kodi akudziwa zamseri,
kotero kuti Akuziwona (zomwe
wadza nazo (Mtumiki{SAW} kuti
sizoona)?
36. Kapena sadauzidwe zomwe
zidali M'mabuku a Musa,
37. Ndi Ibrahim amene
adakwaniritsa (Lonjezo la
Mulungu)?
38. Kuti mzimu wamachimo
sungasenze Machimo a mzimu wina
39. Ndi kutinso munthu
sakalipidwa Koma zimene adachita;
40. Ndipo ndithu, ntchito Zake
zidzaonekera.
41. Kenako (munthu)
adzalipidwa malipiro Okwanira
(pantchito zake zimene Amachita).
42. Ndipo ndithu, kwa Mbuye
wako yekha Ndiwo malekezero (a
chilichonse)
9 .ft '9*SC\
V T '9. *Zi'9 \9\'
$mm&
^BSft&JjfiS
Surat 53. An-Najm Juzu 27 I 1147 tv ^j*-i
of *^«Ji ^j>^
43. Ndithu, lye ndiAmene
amapereka Chisangalalo ndi
zoliritsa;
44. Ndipo lye yekha ndiAmene
Amapereka imfa ndi moyo.
45. Ndipo lye ndiAmene
adalenga mitundu Iwiri:
chachimuna ndi chachikazi,
(Anthu ndi zamoyo zina).
46. Kuchokera m'mbewu ya
moyo pamene Imafwamphukira
(m'chiberekero).
47. Ndipo ndithu, ndi udindo
Wake kuukitsa Kwina (pambuyo
pa imfa).
48. Ndipo lye ndiAmene
amapatsa Chokwanira ndipo ndi
Amene Amapatsa chosunga;
49. Ndipo ndithu, lye ndi
Mbuye Wa Nyenyezi Iyo
yotchedwa Shiira;
50. Ndipo lye ndi Amene
adaononga Adi oyamba; (anthu a
Mneneri Hud).
51. Ndi Samudu; (anthu a
Mneneri Swaleh; )sadasiye (ndi
mmodzi Yemwe wa iwo).
52. Ndipo (adawaononganso)
anthu a Nuhi, Kale (asadaononge
Adi ndi Samudu). Ndithu iwo adali
osalungama Ndi olumpha malire
Kwambiri (kuposa Adi ndi Samudu).
ft &1Rf^3j
Surat 53. An-Najm Juzu 27 I n48 I *V *j*-i
df *^cJl 5jj-j
53. Ndi midzi
yotembenudzidwa Kumwamba
kukhala Pansi, pansi kumwamba,
(Ya anthu a Luti), adaigwetsa.
54. Chidaivindikira chomwe
Chidaivindikira (Chilango).
55. Kodi ndimtendere uti
(Mumtendere) wa Mbuye Wako
umene ukuukaikira?
56. Uyu (Mtumiki)
ndimchenjezi mwa Achenjezi
oyamba (amene adachenjezedwa
Nawo anthu a mibadwo yakale)
57. Tsiku lachiweruzo
layandikira.
58. Palibe angaonetse koma
Mulungu yekha.
59. Kodi mukuidabwa nkhaniyi
(Ya Qur'an moikana)?
60. Mungoseka
(mwachipongwe) ndipo
Simukulira (pamene mukuimva
monga Momwe akuchitira
okhulupirira),
61. Ndipo mukunyozera?
62. Mlambireni ndi
kumpembedza Mulungu (Amene
wavumbulutsa Qur'an Kuti ikhale
chiongoko cha anthu).
§&mm
e03Su55M£^^
Surat 54. AI-Qamar Juzu 27 I 1149 I TV *jJM 1 j+&\ oj>-
SURAT AL-QAMAR LIV
Ndime yoyamba m'sura iyi ikufotokoza zakuyandikira kwa
tsiku lachiweruzo ndi kuwachenjeza anthu za chiweruzocho.
Pambuyo pake padza ndime zofotokoza maganizo a osakhulupirira
zozizwitsa za Mulungu ndi kupitiriza kusakhulupirira kwawo.
Ndipo Surayi ikupempha Mtumiki (madalitso ndi mtendere
zikhale naye), kuti awapewe osakhulupirira ndi kuwalekerera
mpaka kufikira tsiku lotuluka m'manda pomwe adzakhale
balalabalala ngati dzombe. Pambuyo pa zimenezi Surayi
yalongosola mbali ya chikhalidwe cha mibadwo yakale pamodzi
ndi aneneri awo ndi chilango chomwe chidawapeza. Ndipo
yafotokoza nkhani ya aliyense wa iwo ndi kutsimikiza kuti
Qur'an ndi yofewa kwa munthu amene akufuna kuilingalira.
Surayi yamaliza ndi kulongosola kuti osakhulupirira a m'
Makka sianyonga ngati mibadwo imene idatsogola, ndi kuti iwo
alibe mtendere ku chilango cha Mulungu. Ndipo kumapeto
kwenikweni Surayi yaopseza otsutsa, za mabwerero awo pa
tsiku limene adzakokedwe nkhope zawo ndi kuponyedwa ku
moto. Kudzanenedwa kwa iwo panthawiyo: "Lawani
kupweteka kwa Jahena imene mumaitsutsa!"
Ndipo oopa Chauta akuwatonthoza powauza kuti adzapita
kumalo awo m'minda ndi m'mitsinje yambiri pokhala pabwino
kwa Mfumu ya mphamvu zoposa.
Surat 54. Al-Qamar Juzu 27 1150 TV *j*-i
o t j^iil ijj^t
Surat Al-Qamar LIV
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Nthawi ya chimaliziro
(Kiyama) Yayandikira ndipo
Mwezi wagawikana.
2. Koma akaona chozizwitsa
akunyoza Ndi kunena kuti: "Awa
ndi matsenga Womkeramkera
patsogolo."
3. Ndipo adatsutsa (choonadi)
ndi kutsatira Zilakolako (zawo
zoipa) koma Chinthu chilichonse
(cha Mulungu) Nchokhazikika.
4. Ndipo ndithu, zidawafika
nkhani Zomwe zili zokwanira
Kuwaopseza.
5. Nzeru zokwana koma
Achenjezi (kwa iwo)
Sanawathandize.
6. Choncho, apewe (iwe
Mtumiki) Osakhulupiria,
(yembekezani) tsiku Loitana
woitana (wa Mulungu) Kuchinthu
chovuta kwambiri, (Chodedwa ndi
mitima).
7. Maso awo ali zyoli chifukwa
Chakuopsa; adzatuluka m'manda
Uku ali ngati dzombe lobalalika
(Chifukwa cha kuchuluka),
oj&&\(&*-3\£Aj
'J>
®p\&\;%m<£Mi
£&r£'&mm>
©
i-''i
^&M&£&&
®^\&s$&
ig&m^g&zz
Siirat 54. Al-Qamar Juzu 27 I 1151 I TV *>'
O t j^ill d jj->
8. Akuthamangira kwa woitana
(uku Atatukula mitu yawo, osatha
Kucheukira kwina).Adzanena
Osakhulupirira (tsiku
lachiweruziro): "Hi nditsiku lovuta
kwambiri."
9. Patsogolo pawo (Aquraishi)
Anthu a Nuhi nawo adatsutsa,
Adamtsutsa kapolo Wathu nanena
kuti: "Uyu ngwamisala!? Ndipo
Adaopsezedwa (ndi kuzunzidwa
Ndi mazunzo osiyanasiyana).
10. (Nuhi) adaitana Mbuye
wake (nati): "Ine ndagonjetsedwa
(ndi anthu anga); Choncho
ndipulumutseni (kwa iwo)."
11. Tidatsekula makomo
akumwamba Ndi madzi otsika
mopitiriza, Mwamphamvu.
12. Ndipo tidaing'amba nthaka
kukhala ndi Akasupe ofwamphuka
madzi Mwamphamvu. Choncho
adakumana Madzi (akumwamba
ndi am' nthaka Kuti awaononge)
pamuyeso Wopimidwa ndi
kulamulidwa (Ndi Mulungu).
13. Ndipo tidanyamula Nuhu pa
chombo Chamatabwa
chokhomedwa ndi Misomali
(yamitengo)
14. Chinkayandama pamadzi
ndi Kuyang'aniridwa ndi Ife. Iyi
ndi Mphoto ya (Nuhi) yemwe
adakanidwa Ndi anthu ake.
ioifc3»ffig^aa^
<^#s3jP8fcui
^iMdtf&s
®$3&*4W
Surat 54. Al-Qamar Juzu 27 I 1152 * V *>i
£ yjti\ 5jj-*»
15. Ndipo ndithu, tidachisiya
(chigumula) Kukhala phunziro
(pakuonongeka kwa
Osakhulupirira ndi kupulumuka
Okhulupirira).Kodi alipo
Wolikumbukira (ndi kupeza nalo
Malango abwino?)
16. Kodi chidali bwanji
chilango Changa ndi machenjezo
Anga (Kwa onyoza!)
17. Ndipo ndithu, taifewetsa
Qur'an kuti Ikhale chikumbutso
kodi alipo Woikumbukira (ndi
kupeza nayo Malango abwino?)
18. (Adi adamtsutsa Mneneri
wawo Hudi), Kodi chidali bwanji
chilango Changa ndi machenjezo
anga Kwa onyoza!
19. Ndithu Ife tidawatumizira
mphepo Yozizira, yaphokoso,
m'tsiku Latsoka lopitirira,
20. Idawazula anthu (kuchoka
m'malo Mwawo ndi kuwaponya
panthaka Ali akufa) ngati matsinde
a Mitengo yakanjedza ozulidwa
M'malo mwake.
21. Kodi chidali bwanji
chilango Changa ndi machenjezo
anga kwa Onyoza!
22. Ndithu, taifotokoza Qur'an
kuti ikhale Chikumbutso. Kodi
alipo Woikumbukira (ndi kupeza
nayo Malango abwino?)
®1®&&W3&
®&b&&£&
®p$&&M^A&>
©,
^3i)\&$<3i&% &wd?
®gSX
'S&3M ^ ffi ^-^ ^&
<3>
Surat 54. AI-Qamar Juzu 27
1153
tV*>i
t j^iil Oj_^-*
23. Asamudu adatsutsa achenjezi.
24. Ndipo adati: "Kodi titsatire
munthu Mmodzi wochokera mwa
ife? Ndithu Ife ngati titamtsatira
ndiye kuti Tili nkusokera ndiponso
misala.
25. Kodi am'vumbulutsira iye
Chikumbutso pakati pathu,
(Pomwe tili nawo oposa iye Pa
ulemerero)? Koma iye
Ndiwabodza ndi wodzitukumula"
26. Mawa lino adzadziwa (tsiku
Lakuwatsikira chilango,) kuti
ndiyani Wabodza wodzitukumula
(iwo kapena Swaleh).
27. (Tidamuuza Mneneriyo
kuti) ndithu Ife titumiza ngamira
yaikazi kuti Ikhale mayeso kwa
iwo. Choncho Adikire, ndipo pirira.
28. Ndipo auze kuti madzi
agawidwa Pakati pawo (ndi
ngamira). Choncho Aliyense ali
ndi tsiku lopita kukatunga.
29. Koma adaitana mnzawo (wa
Mphulupulu). Ndipo adakonzeka
Kupha ngamirayo ndipo adaipha.
30. Kodi chidali bwanji
chilango Changa ndi machenjezo
Anga (Kwa anthu otsutsa)!
31. Ndithu, tidawatumizira
nkuwe Umodzi choncho adakhala
ngati udzu Ndi mitengo youma
yaomanga Khola.
&
^&gfa&$$$i
®%\
ea^sai a *t&&ȣ.
J&W
^^BllA^fy
* M %
Surat 54. Al-Qamar Juzu 27 1154 I TV ^jA-i
1 j^ill 5jj--
32. Ndipo ndithu, taifewetsa
Qur'an kuti Ikhale chikumbutso.
Kodi alipo Woikumbukira (ndi
kupeza nayo Malangizo abwino?)
33. Anthu a Luti adatsutsa
Machenjezo (a Mneneri wawo).
34. Ndithujfe tidawatumizira
chimphepo Champhamvu
(choulutsa miyala Ndi
kuwagenda), kupatula akubanja La
Luti; tidawapulumutsa (ku
Chilangocho) m'bandakucha,
35. (Choncho kupulumukako
kudali) Chisomo chochokera kwa
Ife (Pa iwo). Momwemo ndimo
Timamlipirira wothokoza.
36. Ndipo ndithu (Luti)
adawachenjeza Anthu ake za kulanga
Kwathu koopsa. Koma adakaikira
machenjezo (ake Ndi kumtsutsa).
37. Ndipo ndithu adafuna kwa
iye kuti Awapatse alendo ake (kuti
Achite nawo zauve), koma
Tidafafaniza maso awo (kuti
Ikhale mphoto pa zimene
adafunazo). (Ndipo tidawauza):
"Lawani Chilango Changa ndi
machenjezo Anga."
38. Ndipo chidawadzera
mwadzidzidzi Chilango
chokhazikika, nthawi Yam'mamawa.
39. Choncho (kudanenedwa
kwa iwo) "Lawani chilango
Changa ndi Machenjezo Anga."
^»«j^JS»a*B5S6
%p>£&®0>&&<&
i$&ti^®S&8®&
&2£l££8#£CSS
Surat 54. Al-Qamar Juzu 27 1155 I TV >>i
t yj&\ 5jj~»»
40. Ndipo ndithu, taifewetsa
Qur'an (Kuti ikhale chikumbutso).
Kodi alipo Woikumbukira (ndi
kupeza nayo Malango abwino?)
41. Ndipo ndithu machenjezo
(ondondozana) Adawadzera anthu
a Farawo (ndi iye Mwini;)
42. Adatsutsa zozizwitsa Zathu
zonse (Zimene zidadza kupyolera
m'manja Mwa Aneneri Athu).
Choncho Tidawaononga,
kuononga kwa Wamphamvu;
(Wosapambanidwa). Wokhoza.
43. Kodi osakhulupirira anuwa
ndi Abwino kuposa iwo (kotero
kuti Sadzaonongedwa)? Kapena
Zalembedwa m'mabuku kuti inu
Mdzasiyidwa (sadzakuonongani
monga Momwe adawaonongera
akale?)
44. Kapena akunena kuti: "Ife
Ndiochuluka titha kudziteteza
(Palibe angatipambane)?"
45. (Auze): Gululo
ligonjetsedwa Ndipo athawa ndi
Kutembenuza misana.
46. Koma lonjezo la chilango
chawo ndi Tsiku lachiweruzo,
ndipo tsiku Lachiweruzo ndi
latsoka lalikulu, Lowawa kwabasi
(kwa osakhulupirira).
47. Ndithu, oipa (mwa awa ndi
aja) Alinkusokera ndi nchilango
cha Jahena chopitirira.
&^j^tyQ\$\%j&&
k &i
<&
$
if '.V„9* '>,< ,Atl'*\
®Md&?2%&
@ p\;^\^\^\;^t\a^
^X^<5W*3
Siirat 54. Al-Qamar Juzu 27 11561 *V ^
t yjb\ &jy*
48. Tsiku limene
adzakokedwera kumoto Ndi
nkhope zawo, (kudzanenedwa
Kwa Iwo:) "Lawani zowawa za
Jahena (Ndi kutentha kwake)!
49. Ndithu, Ife tachilenga
chinthu chilichonse Ndi
muyeso(kulingana ndi Zolinga).
50. Ndipo silili lamulo Lathu
(pa chinthu Tikachifuna) koma
liwu limodzi, (Timangoti kwa
chinthucho: "Chitika" Ndipo
chimachitika mwachangu) ngati
Kuphethira kwa diso.
51. Ndipo ndithu, tidawaononga
anzanu (Onga inu osakhulupirira):
Kodi Alipo okumbuka?
52. Ndipo chinthu chilichonse
adachichita Iwowo(padziko
lapansi) Chili mkaundula.
53. Ndipo ntchito iliyonse,
yaing'ono kapena Yaikulu,
idalembedwa; (palibe Chimene
chingamsowe).
54. Ndithu, oopa Mulungu
adzakhala M'minda ya ulemerero
waukulu ndi Mitsinje
(yosiyanasiyana).
55. Pokhala pabwino
pachoonadi, (Popanda mawu
achabe ndi Machimo), kwa Mfumu
yokhoza Chilichonse.
*&V&A$&ty
*j2$tiS^$6*Z
*&&&j®$®&!&
®JMP'$&
Surat 55. Ar-Rahman Juzu 27
1157
TV *>1
oo Ja^lSj^
Surayi ikufotokoza za kuchuluka kwa mtendere wa Mulungu
umene uli pa anthu. Yayamba ndi kutchula dzina la Mulungu
loti "Rahman" ndi kutchula mtendere wopambana wonse,
umene Qur'an ikuphunzitsa. Ndipo kenako yafotokoza za
mtendere umenewo mwatsatanetsatane kusonyeza ukulu wa
Mwini mtenderewo, kusonyezanso mphamvu Zake zoposa kwa
anthu ndi ziwanda kumwamba ndi pansi. Ndipo yasonyezanso
mmene chidzakhalira chilango cha osakhulupirira Jahena, ndi
momwe udzakhalira mtendere wa oopa chauta ku mparadiso.
Surayi yamaliza ndi kupatula Mulungu ku osakhulupirira
osayenerana ndi lye, komanso kumlemekeza ndi kumtamanda.
Surat 55. Ar- Rahman Juzu 27 1 158 t V * jJri
j*J\ Ojj*>
Surat Ar-Rahman LV
kfWT^^VTKWX. jZZ-jf—
S tM$i££
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. (Mulungu) Wachifundo
Chochuluka!
2. Waphunzitsa Qur'an.
3. Adalenga munthu.
4. Adamphunzitsa kuyankhula.
5. Dzuwa ndi mwezi zikuyenda
Mwachiwerengero .
6. Zomera zopanda tsinde ndi
mitengo, Zikulambira (Mulungu
pachilichonse Chimene wafuna
mwa izo).
7. Ndipo thambo adalitukula
kumwamba Ndipo adakhazikitsa
sikelo (Ya chilungamo),
8. Kuti musapyole malire ndi
kuchita Chinyengo poyesa.
9. Choncho yesani sikelo
Mwachilungamo Ndipo
musapungule muyeso.
10. Ndipo nthaka adaiyala (ndi
Kuikonza) kuti ikhale ya
Zolengedwa.
11. M'menemo muli zipatso ndi
mitengo Ya kanjedza yokhala ndi
mapaya (A zipatso).
^~_^ L^
Q^jM^jJl^U-
-^
ty%$
"i*t1i.f
«&2Ji<S£
k^ft$&te&
&JM<&Qmt$K2>,
Siirat 55. Ar-Rahman Juzu 27
1159
rv *>i
j*J\*jy*
12. Ndi mbewu zamakoko (kuti
chikhale Chakudya cha inu ndi
ziweto zanu), Ndipo mulinso
m'menemo mmera Wafungo
labwino.
13. (Inu zolengedwa za
mitundu iwiri, Anthu ndi ziwanda),
kodi ndi Mtendere uti wa Mbuye
wanu umene Mukuukana (kuti
siWake?)
14. Adalenga munthu
kuchokera ku Dongo lolira monga
ziwiya Zadongo,
15. Ndipo adalenga ziwanda
kuchokera Ku malawi a moto
(wopanda utsi.)
16. (Inu zolengedwa za
mitundu Iwiri, anthu ndi ziwanda)
kodi Ndimtendere uti wa Mbuye
wanu Umene mukuukana (kuti
siWake)?
17. Mbuye wa kuvuma kuwiri
Ndiponso Mbuye wa kuzambwe
Kuwiri.
18. (Inu zolengedwa za mitundu
iwiri, Anthu ndi ziwanda), kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake?)
19. Adaika nyanja ziwiri
zokumana (Yamadzi amchere, ndi
yamadzi Ozizira).
20. Pakati pake pali
chitsekerezo, Sizilowana;
§32&&ak£ 6^\j
>*^%;%ck\
h^ ( p£>&QZi\&
%$&z£&&fy&>
® t
ytfivK" ?,\ A <
!^u^o>W
hgtj£i\&» 5<^£Jlcy
tysptdfySp"*'
Surat 55. Ar-Rahman Juzu 27
1160
TV t£-\
o* j*J\i jy *
21. (Inu zolengedwa zamitundu
iwiri, Anthu ndi ziwanda), kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene mukuukana (kuti siWake?)
22. M'menemo mumatuluka
ngale Zing'onozing'ono ndi ngale
Zikuluzikulu.
23. (Inu zolengedwa za mitundu
iwiri, Anthu ndi ziwanda) kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake?)
24. Ndipo (lye) ali nazo zombo
(Zimene zapangidwa ndi manja
Anu), zoyenda panyanja,
zazikuluzikulu Ngati mapiri.
25. (Inu zolengedwa zamitundu
iwiri, Anthu ndi ziwanda), kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake?)
26. Zonse zili pamenepo
(padziko) Nzakutha.
27. Ndipo idzatsala nkhope ya
Mbuye wako Mwini ulemerero ndi
mtendere;
28. (Inu zolengedwa zamitundu
iwiri Anthu ndi ziwanda) kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake?)
29. (Onse) akumwamba ndi
pansi Akupempha lye (zofuna
zawo)! Tsiku lililonse lye
ngotanganidwa (Kupatsa uyu
ulemerero, ndi Kutsitsa uyu).
vsrit'-fc' ^w«/r<
#^»V4^J
%&\;99m&&
Surat 55. Ar-Rahman Juzu 27
1161
rv ^j*-i
$hj\ijf*
30. (Inu zolengedwa zamitundu
iwiri, Anthu ndi ziwanda), kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake?)
31. Posachedwapa (patsiku la
chiweruzo), Tidzaikapo mtima (pa
chiwerengero Chanu (cha zochita
zanu) inu anthu ndi Ziwanda.
32. (Inu zolengedwa zamitundu
iwiri Anthu ndi ziwanda) kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake?)
33. E, inu ziwanda ndi anthu!
ngati Mungathe kutuluka
m'mphepete mwa Thambo ndi
nthaka (pothawa Mulungu),
Tulukani! Simungathe kutuluka
Pokhapokha ndi mphamvu. (Koma
inu Simungathe kutero.)
34. (Inu zolengedwa zamitundu
iwiri Anthu ndi ziwanda) kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siwake?)
35. Mudzathiridwa malawi
amoto ndi Mtovu wamoto
wosungunuka ndipo Simungathe
kudziteteza ku chilango Chimenechi.
36. (Inu zolengedwa za mitundu
iwiri Anthu ndi ziwanda) kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake?)
37. (Kumbuka) pamene thambo
Lidzang'ambika ndi kukhala
®y$^$tife
$&&#&£
.imte^ifc
' u*'\
$k3^Jt&&K&&Z
%
)js*±>
<^m>M%
%%a&%&<j®($
Surat 55. Ar-Rahman Juzu 27
1162
rv>>i
00 j*J\ hr*
Lofiira ngati chikopa chofiira
(Kapena ngati mafuta oyaka),
38. (Inu zolengedwa zamitundu
iwiri Anthu ndi ziwanda) kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake?)
39. Ndipo patsikulo
(long'ambidwa thambo), Munthu
ndi chiwanda, sadzafunsidwa Za
tchimo lake,
40. (Inu zolengedwa zamitundu
iwiri Anthu ndi ziwanda) kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake?)
41. Adzadziwika oipa (pakati pa
anthu Ndi ziwanda) ndi zizindikiro
zawo (Zowazindikiritsa) .Ndipo
Adzagwidwa maliombo awo ndi
Mapazi awo (ndi kuponyedwa Ku
Jahena).
42. (Inu zolengedwa zamitundu
iwiri Anthu ndi ziwanda) kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake?)
43. (Kudzanenedwa
mowadandaulitsa): Iyi ndi
Jahannama yomwe adali Kuitsutsa
oipa.
44. Adzakhala akuyenda pakati
pa moto Ndi pakati pa madzi
owira, Otentha kwambiri.
45. (Inu zolengedwa zamitundu
iwiri Anthu ndi ziwanda) kodi ndi
S^jtf
©c#^»<&
^^&&®^£
€^t#»$
^m^&>
%£^%^$if&*$>
^^®%tiSK
®,±w\''<<X\\,<\<
#^v&*:
Surat 55. Ar-Rahman Juzu 27
1163
XV ftji-i
^^'^
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake?)
46. Koma amene waopa kuti
adzaimitsidwa kwa Mbuye wake
(pa nthawi yachiweruzo).
Adzalandira minda iwiri (Yaikulu
yamtendere).
47. (Inu zolengedwa zamitundu
iwiri Anthu ndi ziwanda) kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake?)
48. (Minda ya mitengo)
yanthambi Zofwanthamuka.
49. (Inu zolengedwa zamitundu
iwiri Anthu ndi ziwanda) kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake?)
50. M'menemo muli akasupe
awiri, omwe Akuyenda.
51. (Inu zolengedwa zamitundu
iwiri Anthu ndi ziwanda) kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake?)
52. M'menemo muli zipatso za
mtundu Uliwonse, mitundu iwiri
iwiri.
53. (Inu zolengedwa zamitundu
iwiri Anthu ndi ziwanda) kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake?)
54. Atatsamira pa zoyala, mkati
mwake Mosokerera veleveti
£ i
*&&&&%#
$$BC#»9${
\>*
wtetsritii
®«y?l3;&#j e^»££jtj
q$a#s»$
*#£W?JS f e$c&&&'
Surat 55. Ar-Rahman Juzu 27
1164
TV *j*-l
j*J\9jy*
wochindikala; Ndipo zipatso
zam'minda iwiriyi Nzapafupi
(kuzithyola).
55. (Inu zolengedwa zamitundu
iwiri Anthu ndi ziwanda) kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake?)
56. M'mindamo muli akazi
oyang'ana Amuna awo okha basi,
mawuthu, Omwe sadakhalepo
malo amodzi ndi Munthu kapena
chiwanda Asadakumane ndi iwo.
57. (Inu zolengedwa zamitundu
iwiri Anthu ndi ziwanda) kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake?)
58. Kukongola kwake
(akaziwo) kuli Ngati ngale
zikuluzikulu ndi
Zing ' onozing ' ono .
59. (Inu zolengedwa zamitundu
iwiri Anthu ndi ziwanda) kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake?)
60. Malipiro a ntchito zabwino
Ndikulandira zabwino basi.
61. (Inu zolengedwa zamitundu
iwiri Anthu ndi ziwanda) kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake?)
62. Ndipo kuonjezera paminda
iwiri (Ija) palinso minda ina iwiri.
>&&
«MjS^3t$
%$®%>8>m
&$%&$§%
«$BML$®($4
Surat 55. Ar-Rahman Juzu 27
1165 *V *>i
dd J^SjJ-*
63. (Inu zolengedwa zamitundu
iwiri Anthu ndi ziwanda) kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake?)
64. Yobiriwira, kwambiri.
65. (Inu zolengedwa zamitundu
iwiri Anthu ndi ziwanda) kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake?)
66. M'menemo muli akasupe
awiri Ofwamphuka madzi
mwaphamvu.
67. (Inu zolengedwa zamitundu
iwiri Anthu ndi ziwanda) kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake?)
68. Mmenemo muli zipatso:
mitengo Yakanjedza ndi
yamikangaza.
69. (Inu zolengedwa zamitundu
iwiri Anthu ndi ziwanda) kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake?)
70. M'menemo muli akazi
amakhalidwe Abwino, owala
nkhope;
71. (Inu zolengedwa zamitundu
iwiri Anthu ndi ziwanda) kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake?)
72. Okongola maso; achikhalire
M'mahema awo; (Inu zolengedwa
fySU&$9$i
- ifa'
©ttj&*5<^££$£
v*£Vfc,' «u:u
fcMOMCW
©6B338*3S£&
\tm^m
**'•*&&&&
m&swi
Surat 55. Ar-Rahman Juzu 27
1166
TV*>1
00 c» 5 JJ-
zamitundu iwiri Anthu ndi
ziwanda) kodi ndi Mtendere uti wa
Mbuye wanu umene Mukuukana
(kuti siwake?)
73. (Inu zolengedwa za mitundu
iwiri Anthu ndi ziwanda) kodi ndi
mtendere Uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake)?
74. Amene sadakhalepo malo
amodzi Ndi munthu kapena
chiwanda Asadakumane ndi iwo;
75. (Inu zolengedwa zamitundu
iwiri Anthu ndi ziwanda) kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake?)
76. Uku atasamira misamiro
yawofuwofu Yokutidwa ndi
zobiriwira; ndi Zoyala zokongola,
zakapangidwe Kodabwitsa.
77. (Inu zolengedwa zamitundu
iwiri Anthu ndi ziwanda) kodi ndi
Mtendere uti wa Mbuye wanu
umene Mukuukana (kuti siWake?)
78. Latukuka ndi kudalitsika
dzina La Mbuye wako Mwini
ulemerero Ndi ufulu.
m%$&
®J$%$^H>aU
Surat 56. Al-Waqi'ah Juzu 27
1167
TV $->!
1 4*31 jji Ojj-*»
SURAT AL-WAQPAH LVI
Surayi yayamba ndi nkhani yofotokoza zakudza kwa tsiku
lachiweruzo ndi zoopsa zimene zidzatsagana nalo. Kenako
yafotokoza kuti anthu patsiku limenelo adzakhala m'mitundu
itatu. Ndipo yalongosola mwatsatanetsatane za mtundu uliwonse
ndi zomwe mtunduwo wakonzeredwa zolingana ndi ulemerero
wake, kapena chilango cholingana ndi uchimo wake ndiponso
kunyoza kwake.
Kenako yalongosola momveka zizindikiro za mtendere wa
Mulungu, ndi zizindikiro za mphamvu Zake zoposa
pakalengedwe ka anthu, mbewu, madzi ndi moto, ndi kuti
potsatira pazimenezi pakhale kulemekeza Chauta. Ndipo Surayi
yalumbira kuti Qur'ani njolemekezeka ndi kudzudzula
osakhulupirira pa machitidwe awo oipa pakutsutsa kwawo
mmalo mothokoza. Komanso yalongosola mwatsatanetsatane za
mitunduyo, mtendere kapena moto.
Surayi yamaliza ndi kutsimikiza kuti chilichonse
chatchulidwa m'suramo ndi choonadi. Ndipo yalamula
zakulemekeza Mulungu.
Siirat 56. Al-Waqi'ah Juzu27 I H68 I tV>>i o*\ m «A\J\ 5j>-
SuratAl-Waqi'ahLVI
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Chikadzapezeka
chopezekacho (Chiweruzo),
2. Palibe wotsutsa za kupezeka
kwake.
3. Chidzatsitsa (oipa) ndi
kutukula (Abwino);
4. Nthaka ikadzagwedezeka
kwamphamvu,
5. Ndipo mapiri
akadzaperedwaperedwa,
6. Nkukhala fumbi longouluka,
7. Choncho, inu mudzakhala
m'magulu Atatu (kulingana ndi
zochita zanu).
8. Anthu akumanja (abwino;)
taonani Kukula kwa ulemerero wa
anthu Akumanja!
9. Ndi anthu akumanzere (oipa;)
taonani Kuipa khalidwe la Anthu
akumanzere!
10. Ndipo otsogola (pochita
zabwino padziko) Adzakhalanso
otsogola (polandira Ulemu tsiku
lomaliza).
11. Iwowo ndioyandikitsidwa
(kwa Mulungu).
12. M'minda yamtendere.
-fX*. ■ <
mm
O^tfc^l^
**'•&•"'
Surat 56. Al-Waqi'ah Juzu 27 1 169 X V *>•» o 1 tft jit 3jj~,
13. (I wo wo oyandikitsidwawo),
gulu lalikulu Lochokera
kumibadwo yakale.
14. Ndipo ochepa ochokera ku
mbadwo Wotsirizira.
15. Uku ali m'makama
(m'mabedi) Olukidwa ndi zingwe
zagolide,
16. Atatsamira m'makamawo
uku Akuyang'anizana
(mwachikondi).
17. Anyamata osasintha
adzakhala Akuwazungulira iwo
(Ndi kuwatumikira).
18. Uku atatenga matambula
ndi maketulo (Odzazidwa ndi
zakumwa za ku Janat), Ndi
zipanda zodzazidwa ndi zakumwa
Zochokera mu akasupe oyenda;
19. (Zakumwa zake)
Zosapweteketsa mutu Ndiponso
zosaledzeretsa;
20. Ndi zipatso
(zamitundumitundu) Zimene
azikazisankha;
21. Ndi nyama yambalame
imene mitima Yawo izikafuna;
22. Ndi akazi ophanuka Maso
mokongola,
23. (Kukongola kwawo) ndiye
ngati ngale Zosungidwa bwino
mzigoba zake.
®&M&<&&$
*£&&&$&>
Surat 56. Al-WaqFah Juzu 27 1 170 Y V pjk-\ o*\ ** jii ojj-
24. Kukhala mphoto chifukwa
Chazimene amachita (zabwino
Padziko lapansi).
25. M'menemo sakamva mawu
achabe Ngakhale nkhani yamachimo,
26. Koma mawu oti:
"Mtendere! Mtendere!"
27. Anthu akudzanja lamanja.
Taonani Kukula malipiro a anthu
akudzanja Lamanja!
28. (Adzakhala m'mithunzi ya)
mitengo Ya masawo yopanda minga.
29. Ndi mitengo ya nthochi
yobereka Kwambiri.
30. Ndi m'mithunzi
yotambasuka Kwambiri, yosachoka,
31. Ndi madzi oyenda
mosalekeza,
32. Ndi zipatso zambiri,
33. Zopezeka nyengo zonse,
ndiponso Zosakanizidwa (kwa
amene akuzifuna).
34. Ndi zoyala zapamwamba
(zawofuwofu)
35. Ndithu, tidzawalenga (akazi
Okhulupirira) m'kalengedwe
Kapamwamba.
36. Tidzawapanga kukhala
anamwali.
37. Okondedwa ndi amuna awo;
Ofanana misinkhu,
*$&&&$£
$&M
®m&&
Surat 56. Al-Waqi'ah Juzu 27 1171 Y V * >i ^ &\J\ oj^.
38. Aanthu akudzanja la manja.
39. Gulu lalikulu lochokera ku
mibadwo Yakale.
40. Ndiponso gulu lalikulu
lochokera ku M'badwo wotsiriza.
41. Anthu akudzanja
lakumanzere. Taonani chilango
choopsa Kwa anthu akudzanja
lakumanzere!
42. Adzakhala mumvuchi
wamoto Ndi m'madzi owira.
43. Ndi mumthunzi wa utsi
wakuda.
44. Siwoziziritsa ndiponso
Siwosangalatsa.
45. Ndithu, iwo amakhala
kalelo Mosangalala (samalabadira
kumvera Mulungu),
46. Ndipo amapitiriza kuchita
machimo Aakulu (polinga kuti
palibe Kuuka ku imfa).
47. Ndipo amanena (motsutsa):
"Kodi Tidzaukitsidwa tikadzafa,
thupi lathu Litasanduka fumbi ndi
mafupa (ali Ofumbwa),
tidzabwezedwanso Ku moyo
wachiwiri?
48. Kodi ndi makolo athu akale
( Adzaukitsidwanso ! )"
49. Nena kwa iwo (poyankha
kutsutsa Kwawo). Ndithudi,
Surat 56. Al-Waqi'ah Juzu 27 1 172 TV^i on h&\J\ ojj-
amibadwo Yoyamba ndi mibadwo
yomaliza omwe Inu muli m'gulu
lawo,
50. Adzasonkhanitsidwa
m'nthawi Ya tsiku lomwe
lakhazikitsidwa.
51. Kenako inu osokera (njira
Yachilungamo), otsutsa (za kuuka,)
52. Mudzadya (ku Jahena)
mtengo wa Zakkum, (mtengo
wowawa wopezeka Mu Jahena).
53. Mudzakhutitsa mimba zanu
ndi Umenewu (chifiikwa cha njala
Yadzaoneni).
54. (Mkhuto wa mtengowo)
adzamwera Madzi owira;
55. Adzamwa monga mmene
imamwera Ngamira yodwala
matenda aludzu!
56. Hi ndi pwando lawo tsiku
lamalipiro.
57. Ife tidakulengani Kodi
nchifukwa ninji
Simukukhulupirira?
58. Tandiuzani za madzi
(ambewu ya Munthu) amene
mumawathira M'chiberekero,
59. Kodi inu ndiamene
mumawalenga (Madziwo ndi
kumayang'anira Mkusinthasintha
kwake kuti akhale Cholengedwa)
®&^£0i&
$G&J^
Surat 56. Al-Waqi'ah Juzu 27 1 173 TV * >i
0*\ 4*31 jil Ojj^i
kapena Ife ndiAmene
Timawalenga?
60. Ife tidalamula imfa pakati
panu ndipo Ife sitili wolephera,
61. Kubweretsa ena m'malo
Mwanu ndi kukulengani
Mwamaonekedwe ena omwe
Simumawadziwa.
62. Ndipo ndithu,mukudziwa
kalengedwe Koyamba; nanga
bwanji simukuganiza.
63. Tandiuzani za zimene
mukubzala?
64. Kodi ndinu amene
mukuzimeretsa Kapena Ndife
Amene tikuzimeretsa?
65. Tikadafuna
tikadazitembenuza (Mbewu
zimenezo kukhala zouma
Isanakwane nthawi yake
yozithyola) Choncho mukadakhala
mukudandaula.
66. (Uku mukunena:) "Ndithu,
ife tili M'mangawa;
67. Koma Ife tamanidwa
(phindu la Khama lathu)."
68. Kodi mukuwaona madzi
amene Mukumwa!
69. Kodi ndinu amene
mudawatsitsa Ku mitambo kapena
Ndife Amene Timawatsitsa?
S&rjflb
Surat 56. Al-Waqi'ah Juzu 27 I 1174 I YV *>i 01 4*31^1 Sjj-
70. Tikadafuna tikadawapanga
Kukhala amchere; nanga
Nchifukwa ninji Simuthokoza?
71. Kodi mukuwuona moto
umene Mumaukoleza?
72. Kodi ndinu amene
mudameretsa Mitengo yake
kapena Ndife tidaipanga?
73. Ife taupanga kuti ukhale
chikumbutso (Chamoto watsiku
lomaliza akauona), Ndikuti ukhale
chothandiza kwa anthu Apaulendo
(amene akuyenda M'chipululu).
74. Choncho, pitiriza
kulemekeza Dzina la Mbuye Wako
Wamkulu.
75. Ndikulumbirira
motsimikiza, mmene Mumatsikira
nyenyezi (pomwe Zikulowa),
76. Ndithu, kulumbira uku,
mukadakhala Olingalira,
nkwakukulu kwabasi (Pazimene
kukusonya).
77. Ndithu, iyi ndi Qur'an
yolemekezeka (Ndipo mkati
mwake muli zithandizo Zambiri).
78. Idachokera mu buku
lotetezedwa;
79. Salikhuza kupatula okhawo
oyeretsedwa (Angelo).
80. Chivumbulutso chochokera
Kwa Mbuye wa zolengedwa zonse.
©&%&9pZ&\><&?$&>)
6©j3##ij&!ftK
§tim^
@JJ^I^J»iuAx-*
)^s^0!Cyj^U fO~A
^i^i^
®frS£&PA*&
&&®m
Siirat 56. Al-Waqi'ah Juzu 27 1 175 Y V *>»
o*\ **3\jl\ 5jj-»
81. Kodi kuitsutsa (Qur'an)
nkhani iyi, Inu mukuinyozera?
82. Kodi mwakuchita kukanira
kukhala Kuthokoza kwanu pa
Zimene wakupatsani?
83. Kodi bwanji (mzimu wa
mmodzi wa inu) Ukafika kummero
(Panthawi ya imfa),
84. Uku inu panthawi imeneyo
mukuona Zimenezo,
85. Pomwe Ife tili pafupi ndi
iye Kuposa inu, koma inu
simuona,
86. Mukadakhala kuti
simuzalipidwa (Pa zomwe
mukuchita)
87. Bwenzi mukuubweza
(mzimuwo) ngati Mukunena zoona.
88. Ngati (amene yamfikira
imfayo) adali Mmodzi wa
woyandikitsidwa (kwa Mulungu;)
89. Kobwerera kwake ndi
kumpumulo Ndi kumtendere ndi
kupatsidwa Zonunkhira ndiponso
Munda wa Mtendere.
90. Ndipo ngati adali mmodzi
wa anthu Akudzanja lamanja,
91. (Kudzanenedwa kwa iye:)
"Mtendere Ukhale pa iwe, amene
udali m'gulu La anthu akudzanja
lakumanja (Anthu abwino)."
**&&&&&
Siirat 56. Al-Waqi'ah Juzu 27 11761 * V *>i
o*v Zf&\j)\ 5jj-*»
92. Koma ngati adali Mmodzi
wa anthu Otsutsa, osokera,
93. Phwando lamadzi owira
(ndilake),
94. Ndi kupsa m'moto wa
Jahena.
95. Ndithu, izi (zatchulidwa
m'surayi) Ndizoona;
zotsimikizika.
96. Choncho lemekeza dzina la
Mbuye wako Wamkulu.
9 '&*'\ 9 £ 6
k^ffiOpjAfir*
Siirat 57. Al-Hadid Juzu 27
1177 TVtji-l OV JUJLi-l Ojj^.
Surayi yayamba ndikufotokoza kuti zonse zakumwamba ndi
zapansi zimalemekeza Mulungu ndi kumyeretsa pamakhalidwe
osayenerana ndi ulemerero Wake. Ndi kunena kuti Mulungu ndi
Mwini wa zonse zakumwamba ndi zapansi. Ndi kutinso akudziwa
bwinobwino zam'menemo ndi kuzichita mmene angafunire.
Kenako surayi yalamulanso zakukukhulupirira mwa Mulungu
ndi kupereka chuma panjira Yake. Ndipo yalongosola kusiyana
kwa ulemerero wakupereka chuma panjira ya Mulungu
chifukwa cha kusiyana zifukwa zoperekerazo.
Ndiponso yasonyeza maonekedwe pa tsiku lachiweruzo a
okhlupirira pamene kuunika kwawo kudzawatsogolera patsogolo
pawo ndi m'mbali mwawo. Ndipo yasonyezanso maonekedwe a
achinyengo pamene iwo azikapempha okhulupirira kuti awadikire
ndi kuwagawirako kuunika kwawo. Koma pakati pawo padzaikidwa
mpanda wokhala ndi khomo; mbali yamkati mwake muli chifundo
cha Mulungu, ndipo mbali yakunja kwake kuli chilango cha Chauta.
Komanso surayi yalimbikitsa okhulupirira kuti akumbukire
Mulungu ndi kudzichepetsa pa choonadi chimene chavumbulutsidwa.
Ndipo ikuwonetsanso ulemerero wa okhulupirira achimuna ndi
achikazi kwa Mbuye wawo, ndi kobwerera kwa osakhulupirira
otsutsa, ku Jahena. Ndipo kenako Surayi yapereka fanizo
lakunyozeka kwa dziko lapansi ndi zonse za m'dziko, ndi ukulu
wa tsiku lomaliza ndi zonse zili m'menemo. Ndipo ikupempha
kuti tichite changu pofunafuna chikhululuko cha Chauta
ndiponso ikutonthoza mitima pachinthu chilichonse chomwe
chimaupeza mtima: chabwino kapena choipa, ponena kuti
chilichonse, chabwino kapena choipa chidalembedwa m'buku
kwa Mulungu; potero kuti munthu agonjere chiweruzo cha Chauta.
Surayi yafotokozanso za kutumizidwa kwa aneneri ndi
kutsatizana kwawo uku atalimbikitsidwa ndi zizizwa, mabuku
ndi zina zowapatsa mphamvu kuti agwire ntchito ya ulaliki kuti
anthu akhale molungama.
Ndipo pomaliza surayi yapempha Asilamu kuti aope
Mulungu. Ndipo yawalonjeza za chifundo chambiri chomwe
palibe angachidziwe koma Mulungu yekha.
Surat 57. Al-Hadid Juzu 27
1178
YV*>l
OV OjO^I 5jj-»
Surat Al-Hadid LVII
^ -■t jv^ — r j?v l- ^- — ^g=
^M£
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Chilichonse chakumwamba
ndi Chapansi chikulemekeza
Mulungu (Ndi kumyeretsa
kumakhalidwe Opunguka) ndipo
lye ndiMwini Mphamvu, Wanzeru.
2. Ufumu wakumwamba ndi
pansi, Ngwake amapereka moyo
ndi imfa. Ndipo lye
Ngwamphamvu pa Chilichonse.
3. lye alibe chiyambi; (adalipo
Chilichonse chisadayambe);
Wamuyaya, (zonse zikazatha);
Woonekera (mzisonyezo pachinthu
Chilichonse), wobisika mkati
Kwambiri, (saonedwa ndi maso
Pamoyo uno) lye Ngodziwa
Chilichonse (kunja ndi mkati
mwake).
4. lye ndiAmene adalenga
kumwamba Ndi pansi (ndi zonse
zam'menemo) M'masiku asanu
ndi limodzi Ndipo kenako
adakhazikika Pampando Wake
wachifumu (monga Momwe lye
adziwira polongosola Ufumu
Wake). Akudziwa Chilichonse
cholowa m'nthaka ndi Chimene
chikutuluka m'menemo; ndi
Chilichonse chimene chikutsika
o^ifc^JMki,
"***-
JK^feWPA^
wm
Surat 57. Al-Hadid Juzu 27
1179
YV*>1
OV JbJLM djj*-
Kumwamba ndi chimene
chikukwera Kumeneko.Ndipo lye
ali nanu paliponse Pamene muli.
Ndithu, Mulungu Amaona
chilichonse chimene Mukuchita,
(sichibisika chilichonse Kwa lye).
5. Ufumu wakumwamba ndi
pansi Ngwake Ndipo kwa
Mulungu nkobwerera zinthu (Za
zolengedwa zake).
6. Usiku amawulowetsa mu
usana, Ndipo usana amawulowetsa
Mu usiku. (Choncho kumasiyana
Kutalika kwake); ndipo lye
Ngodziwa Zobisika za m'zifuwa
(ndi zoganiza Za m'mitima).
7. Khulupirirani mwa Mulungu
ndi Mthenga Wake, ndipo perekani
(Panjira ya Mulungu m'chuma
chimene Mulungu wakupatsani
kuchiyang'anira. Choncho mwa inu
amene akhulupirira (Mwa Mulungu
ndi mthenga Wake) Ndikupereka
(zimene awapatsa) iwo ali Ndi
malipiro aakulu (kwa Mulungu)
8. Kodi nchifukwa ninji
simukhulupirira Mwa Mulungu
pomwe Mneneri Akukuitanani kuti
mukhulupirire Mbuye wanu (ndi
kukulimbitsani pa Zimenezo)
chikhalirecho (lye) Adalandira
lonjezo lanu, (muli Mumsana wa
atate wanu Adamu Kuti
mdzakhulupirira,) ngati mulidi
Okhulupirira.
£}M&<JM^\m$
<%8\
Siirat 57. Al-Hadid Juzu 27
1180
tV^i
OV -UJL^I Ojj-*
9. lye ndiAmene
akuvumbulutsa kwa Kapolo Wake
aya (ndime) zafotokoza
Mwatsatanetsatane kuti akutulutseni
Mum'dima (wa kusokera) ndi
kukuikani Ku chiongoko cha
kuunika. Ndipo ndithu, Mulungu
Ngoleza kwa inu, Ngwachisoni.
10. Kodi ndichifukwa chiani
Simukupereka panjira ya Mulungu
(Chuma chanu) pamene Mulungu
Ndimwini wa zosiyidwa zonse
Zakumwamba ndi zam'dziko
lapansi. Sali ofanana mwa inu
amene adapereka Chuma (panjira ya
Mulungu) pamodzi Ndi kumenya
nkhondo usadagonjetsedwe
Mzinda wa Makka, iwowo
ndiomwe Ali ndi ulemerero
waukulu kuposa Amene apereka
chuma chawo ndi Kumenya
nkhondo pambuyo. Koma Onsewo
Mulungu wawalonjeza zabwino
(Ngakhale ali osiyana ulemerero
wawo); Ndipo Mulungu akudziwa
zonse zimene Muchita. (Choncho
aliyense Adzalipidwa molingana
ndi zimene Amachita).
11. Kodi ndani wokhulupirira
amene Angamkongoze Mulungu
ngongole Yabwino kuti
amuonjezere (zambiri) Malipiro
ake? Ndipo iye Adzalandira
malipiro aulemu (Pa tsiku
lachiweruzo.)
Surat 57. Al-Hadid Juzu 27
1181
rv *>i
OV JUJU-I 5jj^
12. Tsiku limene udzaona
okhulupirira Achimuna ndi
achikazi Kukutsogolera kuunika
kwawo Patsogolo pawo ndi
chakumanja kwawo (Uku angelo
akunena kwa iwo): "Chisangalalo
chanu lero ndi minda Imene pansi
pake pakuyenda mitsinje.
(Simdzatuluka) m'menemo mpaka
Muyaya! Kumeneku ndiko
Kupambana kwakukulu (kwa inu).
13. Tsiku limene achinyengo
achimuna ndi Achinyengo achikazi
adzauza okhulupirira (Kuti:)
"Tidikireni kuti tipeze Kuunika
kwanu!" Kudzanenedwa
(Mwachipongwe): "Bwererani
pambuyo Panu mukafune kuunika
kumeneko!" Ndipo padzaikidwa
mpanda pakati pawo (Okhulupirira
ndi achinyengo) Umene udzakhala
ndi khomo, mkati Mwa
mpandawo, (komwe ndi kumbali
Ya ku Jannat) muli chifundo ndi
Mtendere; kunja kwake, (komwe
ndi Kumbali yamoto), kuli
mazunzo Ndi chilango.
14. (Achinyengo) adzaitana
okhulupirira Ponena kuti: "Kodi
sitidali nanu limodzi (Padziko ndi
kumatsagana nanu?"
(Okhulupirira) adzati: "Inde!
(Mudali Nafe monga momwe
mukunenera). Koma Inu
munadziononga nokha ndipo
$&&\
^sfiwy*^ sy "' "—
Surat 57. Al-Hadid Juzu 27
1182
rv ftjJt-i
OV JbJj-l djj~-
Mumayembekezera (kuti
okhulupirira Awapeze mavuto ndi
kuonongeka); Mudakaikira (zinthu
za chilengedwe Chanu); choncho
zikhulupiriro zanu Zonama
zidakunyengani pomwe mudali
Angwiro mpaka lamulo la
Mulungu (imfa) Lidakupezani,
komanso adakunyengani Onyenga
(satana) za Mulungu.
15. Basi lero sililandiridwa dipo
Lochokera kwa inu (limene
Mungalipereke kuti
mudzipulumutse Ku chilango
ngakhale likhale Lamtengo
wotani). Ndiponso Sililandiridwa
dipo lochokera kwa Osakhulupirira
(amene adalingana nanu
N'kusakhulupirira kwawo
Mulungu) Malo anu nonsenu ndi
kumoto basi. Amene wa ndi malo
okuyenerani. Kumeneko ndiko
kobwerera koipa Kwabasi!
16. Kodi siidayandikire nthawi
kwa Okhulupirira kuti mitima
yawo Idzichepetse pokumbukira
Mulungu Ndi zomwe
zidavumbulutsidwa za Chowonadi
(Qur'an yolemekezeka)? Ndi Kuti
asakhale monga omwe
adapatsidwa Buku kale (Ayuda ndi
Akhrisitu) Amene nthawi yawo
yosiyana ndi Aneneri awo idali
yaitali. Choncho mitima yawo
idauma ndipo Ambiri aiwo adatuluka
m'chilamulo (Cha Mulungu).
'}$&'jn$3W$
©jL^Jl
©■
IjyL*
Surat 57. Al-Hadid Juzu 27 I H83 I rv s-ji-^ oV Jb>M 5j_^
17. Dziwani kuti Mulungu
amaukitsa Nthaka itauma
(poitsitsira mvula kuti Mmera
umere) . Choncho
Takulongosolerani zisonyezo kuti
inu Mukhale ndi nzeru.
18. Ndithu amene akupereka
sadaka, Amuna ndi akazi, ndi
kumamkongoza Mulungu ngongole
yabwino (Mulungu) Adzawaonjezera
malipiro pa zimenezi. Ndipo ali
ndi malipiro aulemu
19. Ndipo amene akhulupirira
Mulungu Ndi aneneri Ake, iwowo
ndiwo oona (Pa chikhulupiriro);
ndi ofera panjira ya Mulungu
(onsewo) azapeza malipiro Awo
ndi kuwala kwawo kwa Mbuye
Wawo. Koma amene
sadakhulupirire Ndi kutsutsa
zisonyezo Zathu Iwowo ndi eni a
ku Jahena.
20. Dziwani kuti ndithu, moyo
wapadziko Lapansi ndimasewero,
wachabe Chokometsera chabe,
Chonyadiritsana pakati Panu
(paulemerero) ndi kuchulukitsa
Chuma ndi ana (pomwe zonsezo
Sizikhala nthawi yayitali;) fanizo
lake Lili ngati mvula yomwe
mmera wake Umakondweretsa
alimi; kenako Umauma, ndipo
uuona uli wachikasu; Kenako
nkukhala odukaduka
(Oonongeka).Koma tsiku lomaliza
Surat 57. Al-Hadid Juzu 27
1184
TV*>»
OV JbJL^t djj-*.
kuli Chilango chaukali; ndi
chikhululuko Komanso chikondi
chochokera kwa Mulungu.Moyo
wapadziko lapansi suli Kanthu, koma
ndichisangalalo Chonyenga basi.
21. Chitani changu (pa zinthu
Zokupatitsani) chikhululuko
chochokera Kwa Mbuye wanu ndi
munda wa Mtendere womwe
mulifupi mwake Muli ngati
kutambasuka kwa kumwamba Ndi
pansi; wakonzedwera amene
Akhulupirira Mulungu ndi aneneri
Ake; Umenewo ndi ubwino wa
Mulungu Womwe akuupereka kwa
amene Wamfuna. Mulungu Ndi
Mwini ubwino waukulu.
22. Silipezeka tsoka lililonse
panthaka (Monga chilala) ngakhale
pamatupi Anu koma lidalembedwa
kale m'Buku (La Mulungu)
tisadalilenge ndi Kulipereka.
Ndithu zimenezo Kwa Mulungu
nzofewa.
23. (Takudziwitsani zimenezi)
kuti Musadandaule ndi chimene
Chakudutsani, ndi kutinso
Musakondwere monyada ndi
chimene Wakupatsani. Mulungu
sakonda Aliyense wodzitama,
wonyada,
24. Amene akuchita umbombo
(ndi chuma Chawo; ndipo
osapereka panjira ya Mulungu) ndi
kumalamula anthu ena Kuchita
Surat 57. Al-Hadid Juzu 27
1185
tY*>i
OV OjOJ-I O^j-
umbombo ndipo amene
Atembenuke (adzalandira chilango
Chachikulu), ndithu,Mulungu
Ngolemera, (sasaukira chilichonse
Kwa wina);Ngotamandidwa.
25. Ndithu, tidatuma aneneri
Athu Pamodzi ndi zozizwitsa.
Ndipo Tidavumbulutsa pamodzi
ndi iwo mabuku Ndi muyeso wa
choonadi kuti anthu achite
Chilungamo. Ndipo tidalenga
chitsulo Momwe muli mphamvu
zambiri (pa Nkhondo) ndiponso
chithandizo kwa anthu (Akakhala
pa mtendere ndi kupindula Nacho
pochita zowathandiza pa moyo
Wawo). Ndi kuti Mulungu
amuonetsere Poyera, amene
angachiteteze (chipembedzo
Chake) ndi aneneri Ake
(Kupyolera m'chitsulocho) pomwe
lye Sakumuona. Ndithu, Mulungu
Ngwamphamvu (pa chilichonse)
Ngopambana
26. Ndipo ndithu tidatuma Nuhi
ndi Ibrahim ndi Kukhazikitsa
uneneri m'mbumba yawo Ndi
mabuku (achiongoko). Ena mwa
Iwo adayenda panjira yolungama,
Koma ambiri a iwo adapatuka
panjira Yolungamayo.
27. Kenako tidatsatiza pambuyo
Pawo ndi aneneri athu ndipo
Tidasatiza ndi Isa mwana wa
Mariamu, ndipo tidampatsa Injili
Surat 57. Al-Hadid Juzu 27
1186
TV *jJfe-i
OV JUJL^I Ojj-*»
ndipo tidaika kufatsa Ndi chifundo
m'mitima Ya omwe adamtsatira.
Koma kusakwatira,
Adakuyambitsa okha;
Sitidawalamule zimenezo Koma
(adayambitsa zimenezo) Chifukwa
chofuna chikondi Cha Mulungu;
koma Sadazisunge moyenera.
Choncho amene adakhulupirira
Pakati pawo tidawapatsa Malipiro
awo, koma Ambiri a iwo ngolakwa
28. E, inu amene
mwakhulupirira! Opani Mulungu,
Ndipo khulupirirani Mthenga
Wake, Akupatsani zigawo ziwiri
za chifundo Chake. Ndipo
akupangirani kuunika koongoka
nako (Poyenda patsiku
lachiweruzo.) Ndiponso
Akukhululukirani ndipo Mulungu
Ngokhululuka mochuluka
kwambiri, Ngwachisoni.
29. (Mulungu akupatsani
zonsezi) kuti Adziwe amene
adapatsidwa Buku (omwe
Sadamkhulupirire
Mtumiki{SAW}) kuti iwo
Sangathe kudzisankhira okha
chilichonse Mumtendere wa
Mulungu. Ndipo ndithu, Ubwino
wonse uli m'manja mwa Mulungu
Yekha.Amapatsa amene wamfuna
mwa Akapolo ake. Ndipo
Mulungu ndi Mwini Ubwino
wochuluka.
'*l, U 99**
w&^ss&j^£
%sw«
^ ,-^t
Surat 58. Al-Mujadilah Juzu 28
1187
tA*>l
OA A^l^l Ojj-j
Surayi yayamba ndikufotokoza nkhani ya mkazi amene
adasalidwa ndi mwamuna wake. Ndi za lamulo losala mkazi.
M'sura imeneyi Mulungu wanena m'ndime zochulukirapo za
amene amada chipembedzo Chake ndi kuwachenjeza za
kunong'onezana za machimo ndi mtopola. Ndipo wawaongolera
Asilamu kumwambo wonong'onezana pakati pawo, ndi pakati
pa Mneneri (madalitso ndi mtendere zikhale naye) ndi iwo.
Ndipo kenaka surayi yapitirira ndi kudzudzula achinyengo
m'kuyanjana kwawo ndi osakhulupirira ndi kuwatcha kuti ndi
eni chipani cha satana; otaika. Ndipo yamaliza ndi kusimba
khalidwe loyenera kukhala nalo okhulupirira; kumene kuli
kusankha chikondi cha Mulungu ndi Mneneri Wake (madalitso
ndi mtendere zikhale naye) kuposa wina aliyense ngakhale
atakhala bambo wawo, ana awo, abale awo, kapenanso akubanja
lawo. Ndipo anthu otero yawatcha kuti ndi wo achipani cha
Mulungu, chopambana.
Surat58.Al-Mujadilah Juzu28 I H88 I *A *>i
oA 4tal£i Sjj~»
SuratAl-Mujadilah LVIII
.w~
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Ndithu Mulungu wamva
mawu a (amkazi) Amene
akubwezeranabwezerana nawe
(Mawu) pa za mwamuna wake
(amene Adamsala); ndipo akusuma
kwa Mulungu. Ndipo Mulungu
akumva Kukambirana kwanu;
Ndithu, Mulungu Ngwakumva
Ngopenya (chilichonse). 1
2. Amene akufanizira mwa inu
(Asilamu) Akazi awo (ndi amayi
awo) iwo siamayi Awo; amayi
awo ndiamene adawabereka.
Ndithu,iwo akunena mawu oipa
ndi onama. Koma ndithu, Mulungu
ali Wofafaniza (Machimo) ndi
Wokhululuka (Amene walapa).
3. Amene akuwafanizira akazi
awo (ndi Amayi awo) kenako
nkubweza zimene Adanena,
apereke ufulu kwa kapolo
Asanakhale malo amodzi (ndi
mm
^^*
».
Arabu adali ndi chizolowezi chakupatukana ndi mkazi. Izi zimachitika
akanena mawu akuti: "Ndikukuyerekeza ngati mayi wanga." Choncho
amangokhala naye mkazi uja, osamkhudza ndiponso osamulola kuti akwatiwe
ndi mwamuna wina. Samamchitiranso zimene munthu amachitira mkazi wake
monga kumveka ndi kumdyetsa.
Msilamu wina adamsiya mkazi masiyidwe onga amenewa ndipo mkazi uja
adapita kukakambirana naye Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye).
Choncho Chisilamu chidaletsa machitidwe onga amenewa.
Surat 58. Al-M ujadilah Juzu 28
1189
YA*>I
OA ibl^l djj~t
mkaziyo). Amenewa ndi malamulo
a Mulungu kwa Inu (amene)
mukuchenjezedwa nawo. Ndipo,
Mulungu akudziwa zimene
Mukuchita (zoonekera poyera ndi
Zosaonekera choncho sungani
Malamulo amene Mulungu
Wakhazikitsa pa inu).
4. Ndipo amene sadapeze
(kapolo) amange Miyezi iwiri
yondondozana Asadakhalirane
pamodzi (ndi mkaziyo), Koma
amene sadathe kumanga adyetse
Masikini makumi asanu ndi
limodzi (60). Malamulo amenewa
aikidwa kuti Mukhulupirire mwa
Mulungu ndi Mthenga Wake.
Amenewo ndiwo malire A
Mulungu; (malamulo
okhazikitsidwa Ndi Mulungu
choncho musawalumphe). Ndipo
chilango chopweteka chili pa
Osakhulupirira.
5. Ndithu, amene akutsutsana
ndi Mulungu Kudzanso Mthenga
Wake, ayalutsidwa Monga momwe
adayalutsidwira amene adalipo
Patsogolo pawo; ndithu
tavumbulutsa aya Zolongosola,
momveka (pa zololedwa ndi
Zoletsedwa). Ndipo chilango
Choyalutsa chili pa osakhulupirira.
6. (Kumbuka) tsiku limene
Mulungu Adzaukitsa akufa onse
ndi Kuwafotokozera zimene
<S&S»
8^f*#wWi
Surat58.Al-Mujadilah Juzu28 I H90 I tA *jju»
OA ibbfcl djj^>
adachita (Pa moyo wa dziko
lapansi: zoipa ndi Zabwino;
Mulungu) adazisunga Mozilemba
koma iwo adaziiwala. Ndipo
Mulungu ndi mboni wa zonse
(Palibe chingabisike kwa lye).
7. Kodi sukudziwa (iwe,
womvera Wanzeru) kuti Mulungu
akudziwa Zakumwamba ndi
zam' dziko lapansi? Sipakhala
manong'onong'o a (anthu) Atatu
koma lye ngwachinayi wawo (Ndi
kudziwa kwake kosabisirika
Chilichonse cha kumwamba ndi
M' dziko), ngakhale a (anthu)
asanu Koma lye Ngwachisanu ndi
chimodzi Wawo (mkudziwa
Kwake), ngakhale ali ochepera
kuposera pamenepa kapena
Ochulukira koma lye Ali nawo
paliponse pomwe ati akhale
(Mulungu ali nawo pamodzi
mukudziwa Kwake kosabisika
chilichonse), kenako
Adzawafotokozera pa tsiku
lachiweruzo Zimene adachita;
ndithu, Mulungu Ngodziwa
chilichonse (mokwanira). 1
8. Kodi sudaone! kwa amene
aletsedwa Kunong'onezana zoipa
pakati pawo, Kenako akubwereza
M'ndime iyi, Mulungu akutichenjeza kuti pamene tikuchita kalikonse
tisamaganizire kuti Mulungu sakutiona. Palibe chimene chingabisike kwa
Mulungu cha m'dziko lapansi kapena kumwamba; m'zoyankhula kapena
m'zochitachita.
Surat58.Al-Mujadilah Juzu28 1191 I TA;>i
OA ibbfcl djj^
zimene Adaletsedwa?
Akunong'onezana za Machimo,
mtopola ndi kunyoza Mtumiki.
Akakudzera akukulonjera (Ndi
malonje achinyengo) amene
Mulungu sadakulonjerepo nawo
ndipo Akunena m'mitima mwawo:
"Kodi Nchifukwa chiyani
Mulungu sakutilanga Ndi mawu
tikunenawa (ngati iyeyu ndi
Mtumikidi wa Mulungu?"
Jahannama Ikuwakwanira:
adzailowa. Ndipo Taonani kuipa
malo (awo) wobwerera! 1
9. E, inu amene mwakhulupirira!
Ngati Mukunong'onezana,
musamanong'onezane za Machimo
ndi mtopola ndi kunyoza Mtumiki:
Koma nong'onezanani za
kulungama Ndi kuopa Mulungu
ndipo muopeni Mulungu, Kwa lye
nkumene mudzasonkhanitsidwe
(ndi Kuweruzidwa).
10. Ndithu, manong'onong'o
oipa Amachokera kwa satana kuti
Adandaulitse amene akhulupirira;
Koma sangawapweteke nawo
Chilichonse kupatula Mulungu
atafuna Ndipo okhulupirira
atsamire kwa Mulungu yekha,
(asalabadire Zonong'onezana zawo)
Ayuda amamlonjera Mtumiki ndi mawu akuti: "Saamu alayikumu"
kutanthauza kuti: Imfa ikhale pa inu. Amayankhula mokhotetsa lirime kuti
ampusitse Mtumiki kuti aganizire kuti akumlonjera moyenera kuti: "Asalamu
alayikumu."
Sfirat 58. Al-Mujadilah Juzu 28
1192
TAfr>»
3 A iJibrl 5jj-j
11. E, inu amene
mwakhulupirira! Kukapemphedwa
kwa inu kuti perekani Malo
pabwalo (pokhala); perekani
Malowo (kuti anzanu apeze
pokhala; Mukatero) Mulungu
akuphanulirani (Chifundo Chake
pano padziko ndi
Kumwamba).Ndipo kukanenedwa
kuti Imirirani, muimirire
(musanyozere, Apatseni ena malo);
Mulungu Awakwezera (ulemerero)
mwa inu Amene akhulupirira ndi
amene Apatsidwa nzeru. Ndipo
Mulungu Akudziwa bwino zimene
mukuchita. 1
12. E, inu amene
mwakhulupirira! Mukafuna
kuyankhula ndi Mtumiki(SAW)
Tsogozani pazoyankhula zanuzo,
Sadaka: kutero ndibwino kwa inu
Ndiponso ndichoyeretsa (mitima
1 Kuvumbulutsidwa kwa ndime iyi pali mawu akuti: Mtumiki (madalitso ndi
mtendere zikhale naye) amaikira mtima kwambiri pa anthu amene adamenya
nkhondo ya Badir; amgulu la Amuhajirina ndi Answari.
Ndipo ena mwa iwowa adadza pa bwalo la Mtumiki ndi kupeza anthu ena
atakhala kale Adakhala chiimire chifukwa chosowa pokhala uku
akuyembekezera kuti anzawo aja awapatseko pokhala; koma anthu adakhala
kale aja sadalabadireko chilichonse. Mtumiki ataona izi zidamuwawa
mumtima ndipo adawauza omwe adakhala kale aja kuti aimirire apereke malo
kwa anzawo. Amunafikina adayamba kum'dzudzula Mtumiki (madalitso ndi
mtendere zikhale naye) kuti bwanji akuchotsa anthu okhalakhala pamalo
chifukwa cha anthu obwera mochedwa; sikupanda chilungamo kumeneko?
Adatero Amunafikina aja. Ndipo poyankha zimenezi Mulungu adati: "E, inu
okhulupirira! Mukauzidwa kuti perekani malo kwa anzanu mupereke. Ndipo
mukauzidwa kuti imirirani, muimirire."
M'ndime imeneyi Mulungu akutiphunzitsa kuti timvere Mtumiki(SAW) pa
chilichonse chimene watilangiza popanda kuwiringula.
Surat 58. Al-Mujadilah Juzu 28
1193
ta*>i
oA 4bl£i ojj--
yanu). Koma ngati simudapeze
(sadakayo) Ndithu, Mulungu
Ngokhululuka, Ngwachisoni.
13. Kodi mwaopa kutsogoza
sadaka Pakunena naye (Mtumiki)?
Ngati Simudachite zimenezi basi
Mulungu wakukhululukirani;
Choncho pempherani swala
moyenera Ndipo perekani zakaat
Ndiponso mverani Mulungu
pamodzi Ndi Mtumiki Wake.
Ndipo Mulungu Akudziwa zonse
zimene mukuchita.
14. Kodi sukuwaona amene
apalana ubwenzi Ndi anthu amene
Mulungu Wawakwiira; iwo sali
mwa inu Ndiponso sali mwa iwo.
Ndipo Akulumbira zabodza uku
akudziwa (Kuti limeneli
ndibodza).
15. Mulungu wawakonzera
chilango Chaukali, ndithudi
zimene amachita Nzoipa.
16. Kulumbira kwawo
adakuchita kukhala Chodzitetezera
(iwo, ana Awo ndi chuma chawo);
choncho Adatsekereza (anthu) ku
njira ya Mulungu; ndipo chilango
Choyalutsa chili pa iwo. 1
$fc%ffl%&yfy!m
Tanthauzo la "Kulumbira kwawo adakuchita chodzitetezera" ndiko kuti
Amunafikina amadziteteza kwa Asilamu pakungosonyeza Ghisilamu
chachiphamaso, chapakamwa pokha pomwe mitima yawo siimakhulupirira.
Amatero pakuopa kuti Asilamu angawachitire zimene amawachitira anthu
osakhulupirira monga kuwathira nkhondo akaputidwa.
Surat 58. Al-Mujadilah Juzu 28 I 1194 I 1 A * >» ©A tai£i 5 j^-.
17. Chuma chawo, ngakhale
ana awo, Sizidzawathandiza konse
ku chilango Cha Mulungu iwowo
ndi Anthu a ku moto m'menemo
Iwo adzakhala muyaya.
18. (Alikumbukire) tsiku limene
Mulungu Adzawaukitsa (ku imfa)
onse, adzayamba Kulumbira kwa
lye (zabodza) monga Akulumbira
(zabodza) kwa inu. Akuganiza kuti
apezapo kanthu (Pakulumbira
kwawo). Dziwani, Ndithudi, iwo
ndi abodza.
19. Satana wawapambana ndipo
Wawaiwalitsa kukumbukira
Mulungu. Iwowa ndiachipani cha
satana. Dziwani Kuti chipani cha
satana nchotayika, (Choonongeka).
20. Ndithudi, amene.
akutsutsana ndi Mulungu ndi
Mthenga Wake. Iwowo Adzakhala
m'gulu la onyozeka.
21. Mulungu adalamula (kuti):
"Ndipambana Ine ndi Aneneri
Anga." Ndithu, Mulungu
ndiwanyonga zokwana
Wopambana; (sapambanidwa ndi
Aliyense).
22. Supeza anthu okhulupirira
mwa Mulungu ndi tsiku lomaliza
akukonda Amene akuda Mulungu
ndi Mthenga Wake, ngakhale
atakhala atate awo, ana Awo abale
awo ndi akumtundu wawo; Kwa
Surat 58. Al-Mujadilah Juzu 28
1195
tAt>!
OA ibl£l $jj*i
iwo (Mulungu) wazika
Chikhulupiriro (champhamvu)
m'mitima Mwawo, ndipo
wawalimbikitsa ndi Mphamvu
zochokera kwa lye. Ndipo
Adzawalowetsa m'minda yomwe
pansi Pake pakuyenda mitsinje;
adzakhala M'menemo muyaya.
Mulungu Adzakondwera nawo
ndipo (iwonso) Adzakondwera
Naye. Iwowa ndi chipani Cha
Mulungu. Dziwani kuti Chipani
cha Mulungu ndichopambana. 1
1 M'ndime imeneyi Chauta akunenetsa kuti: "Amene akukhulupirira mwa
Mulungu ndi Tsiku lomaliza, asapalane ubwenzi ndi munthu wodana ndi
Mulungu ndi Mthenga Wake ngakhale wodana ndi Chautayo atakhala bambo
wake, mwana wake ndi wina aliyense; apatukane nawo ndithu; chifukwa
kupanda kutero akusonyeza kufooka kwa chikhulupiriro. Mtumiki (SAW) adati:
"Munthu adzakhala ndi amene amamkonda pa tsiku Lachiweruzo."
Surat 59. Al-Hashr Juzu 28
1196
YA*j*-i o^yj-lojj^
Surayi yayamba ndi kufotokoza kuti zonse zakumwamba ndi
zapansi pano zikulemekeza Chauta ndi kumuyeretsa ku mbiri
zosayenerana ndi ulemerero Wake, ndi kuti lye ndiwopambana
ndipo sapambanidwa; Wanzeru zakuya pa zochita Zake zonse.
Zina mwazisonyezo za mphamvu Zake ndi nzeru Zake
zakuya, yafotokoza surayi pa kulangidwa kwa Bani Nadhiri
amene adali Ayuda aku Madina. Iwowa adagwirizana ndi
Mneneri kukhalirana mwamtendere. Koma pamene Asilamu
adagonja pankhondo ya Uhud, Bani Nadhiri adaswa panganolo
ndi kugwirizana ndi Akuraishi kumthira nkhondo Mneneri
(madalitso ndi mtendere zikhale naye) ndipo Mtumiki
Muhammad(SAW) pamodzi ndi gulu lake adawazinga ayudawo
m'malinga awo omwe anaganizira kuti angawateteze koma
malingawo sadawateteze, ndipo Mneneri (madalitso ndi
mtendere zikhale naye) adawasamutsa ku Madina.
Kenako surayi yafotokoza za kagawidwe ka chuma cha Fayi-
i. Fayi-i ndichuma chimene asiya adani popanda kubuka
nkhondo kapena kuthamangitsa akavalo. Ndipo yafotokoza kuti
chumacho ncha Mulungu, Mneneri, achibale a Mneneri, ana a
masiye, masikini, munthu wa paulendo ndi osauka amene
adasamuka ndi kusiya nyumba ndi chuma chawo.
Surayi yafotokozanso za Ansari ndi ulemerero wawo; ndi
kuti amatsogoza zofuna za abale awo owasamukira kuposa
zofuna zawo. Ndipo yalongosolanso makhalidwe ena a anthu
achinyengo amene amangosonyeza Chisilamu chawo ndi
pakamwa pokha.
Surayi yamaliza ndi kuchenjeza Asilamu kuti akhale oopa
Mulungu ndi kukonzekera zanthawi yakutsogolo.
Ikuwalangizanso kuti Qur'an ndi Buku la Mawu okoka mtima
limene lidavumbulutsidwa ndi Mulungu, Mwini maina abwino;
palibe wopembedzedwa mwachoonadi koma lye basi.
Surat 59. AI-Hashr Juzu 28
1197 U^i
o ^ j2±\ Sj^
Surat Al-HashrLIX
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Zonse zam'mwamba ndi
zapansi Zimalemekeza Mulungu
(ndi Kumuyeretsa ku khalidwe
losayenera ndi Ulemerero Wake).
Ndipo lye Ngopambana,
(Salephera kanthu) Ngwaluntha
(M'kakonzedwe Kake ndi
m'zochita Zake).
2. lye ndi Amene adatulutsa
osakhulupirira Ena mwa anthu a
Mabuku m'nyumba Zawo
mkusamusidwa koyamba (Pa
chilumba cha (Arabu).
Simunkaganizira kuti angatuluke
(M'nyumba zawozo). Ndipo iwo
Amaganiza kuti malinga awo
awateteza Kwa Mulungu. Koma
Mulungu adawalanga kupyolera
mmene Samayembekezera, ndipo
adathira Mantha oopsa m'mitima
mwawo (Potumiza Mtumiki Wake
kwa iwo), Adagumula nyumba
zawo ndi manja Awo ndi manja a
okhulupirira. Lingalirani
(zimenezi) E, inu eni nzeru! 1
m
Q^lt^l^
J&
,7*v
!T-
1 Aya imeneyi ikulongosola nkhani ya kusamutsidwa kwa Ayuda otchedwa
Bani Nadhiri mu mzinda wa Madina. Ayuda adasamutsidwa mumzinda wa
Madina chifukwa cha kuswa mapangano okhalirana
mwamtendere ndi Asilamu.
Surat 59. Al-Hashr Juzu 28
1198 I 1A*>i
o^ jJi^-l 5jj--
3. Ndipo kukadapanda kuti
Mulungu Adawalembera
(pachiyambi) kusamuka
(M'nyumba zawo), akadawalanga
Padziko pompano; koma chilango
cha Moto chili pa iwo tsiku
lomaliza.
4, Zimenezo nchifiikwa chakuti
iwo Adada Mulungu ndi Mthenga
Wake,(Chidani chopyola muyeso);
ndipo amene Akuda Mulungu
(sangapulumuke ku Chilango
Chake). Ndithu, Mulungu
Ndiwolanga mwaukali.
5. Sim'dadule mtengo uliwonse
wa zipatso Za kanjedza, (inu
Asilamu), kapena Kuusiya uli
chiimire ndi thunthu lake koma
Nchifuniro cha Mulungu ndi kuti
Awayalutse otulukam'malamulo
Ake. 1
6, Ndipo chuma chimene
wapereka Mulungu kwa Mtumiki
Wake Chochokera kwa iwo (Bani
Nadhiri), Chimenecho inu
simudathamangitse Mahachi
kapena ngamira (pakuchipeza)
Koma Mulungu amapereka
mphamvu Kwa aneneri Ake
(Ndime 5-7) Ndime zimenezi zikufotokoza za kagawidwe ka chuma
chosiyidwa ndi adani pankhondo.Chumacho sichongogawira amene amachita
nkhondo okha ayi. Kapena kugawana akulu-akulu okha monga momwe
amachitira ena omwe sali Asilamu pa nkhondo zawo. Chifukwa kutero ndiye
kuti chumacho chizingozungulira pakati pa anthu olemera okhaokha ndi
bwino. Chisilamu chikulamula kuti chuma choterechi chigawidwe kwa onse
kuti umphawi uwachokere onse.
Surat 59. Al-Hashr Juzu 28
1199
YAs-jJrl
O^ j£j-\ djj-»»
zogonjetsera amene
Wamfiina.Ndipo Mulungu ali ndi
Mphamvu (pa) chilichonse.
7. Chuma chimene Mulungu
wachipereka Kwa Mneneri Wake
cha anthu am'midzi (Yapafupi ndi
mzinda wa Madina) Chimenecho
ncha Mulungu, ndi Mneneri, ndi
abale a Mneneri ndi Amasiye, ndi
masikini, ndiponso Apaulendo;
kuti chisakhale Chongozungulira
pakati pa olemera okha Mwa inu.
Ndipo chimene wakupatsani
Mtumiki, chilandireni; ndipo
chimene Wakuletsani chisiyeni.
Muopeni Mulungu (potsatira
malamulo Ake). Ndithu,Mulungu
Ngwaukali polanga.
8. Chiperekedwe kwa osauka
osamuka omwe Adatulutsidwa
m'nyumba zawo Ndi (kusiya)
chuma chawo chifukwa Chofuna
zabwino za Mulungu ndi Chikondi
(Chake) ndi kupulumutsa
Chipembedzo cha Mulungu ndi
Mthenga Wake (potumikira matupi
awo Ndi chuma chawo); Iwowa
ndi (Asilamu) oona.
9. Koma amene adakhala kale
mumzinda Uwu (wa Madina) ndi
kukhulupirira Akukonda amene
adasamukira kwa iwo. Ndipo
sakupeza vuto m'mitima mwawo
Pazimene anzawo apatsidwa,
ndipo Akutsogoza zofuna za
*&"'
i<i)
Surat 59. Al-Hashr Juzu 28
1200 tA*>i
^ j-*^"l *JJ"*'
anzawo pazawo, Ngakhale iwo
akuzifunitsitsa. Amene
Atetezedwa (ndi Mulungu)
kuumbombo Wa mitima yawo,
amenewo ndiwo Opambana.
10. Ndipo (okhulupirira) amene
adadza Pambuyo (pa Amuhajirina
ndi Ansari) Akunena kuti: "Mbuye
wathu Tikhululukireni ndi anzathu
amene Adatitsogolera pa
chikhulupiriro, ndipo Musaike
m' mitima m wathu njiru ndi
Chidani kwa amene
adakhulupirira. O, Mbuye wathu!
Inu ndinu Wodekha Wachisoni."
11. Kodi wawaona achinyengo!
Amene akunena kwa Anzawo
amene sadakhulupirire pakati Pa
anthu a Mabuku: "Ndithu, Ngati
(mukakamizidwa) kutuluka mu
Mzinda wa Madina, tidzatuluka
nanu Pamodzi ndipo sitingamvere
aliyense za Inu mpaka muyaya;
ngati Mutamenyedwa nkhondo
(ndi Asilamu)
Tidzakuthandizani.Koma Mulungu
Akuikira umboni kuti iwo
Ndionama (pazimene alonjeza).
12. Koma akapirikitsidwa,
sangatuluke nawo Limodzi; ngati
atamenyedwa, Sangawathandize
ndipo ngati Atawathandiza
atembenuza Misana (kuthawa)
Kenako sapulumutsidwa.
*-}
Surat 59. Al-Hashr Juzu 28
1201 tA*>i
o S j-iJ-l o j>*»
13. Ndithu, inu (Asilamu)
mukuopedwa Kwambiri m'mitima
mwao kuposa mmene
Akumuopera Mulungu. Zimenezo
Nchifukwa chakuti iwo ndi anthu
Osazindikira (chilichonse).
14. (Ayuda) sangamenyane ndi
inu ali pa Gulu kupatula m'midzi
yotetezedwa Ndi malinga, kapena
kuseri kwa zipupa. Nkhondo yawo
pakati pawo njaukali;
Ungawaganizire kuti ali pamodzi
Pom we mitima yawo njosiyana;
Zimenezo nchifukwa chakuti iwo
Ndianthu opandanzeru.
15. Fanizo (la Ayuda a Banu
Nadhiri) lili Ngati (amene
adatsutsa mwa Ayuda A Kainuka)
amene awatsogolera (Kupeza
mavuto) posachedwapa, Adalawa
chilango (padziko lapansi) Cha
zochita zawo (ndi kuswa
mapangano). Ndipo iwo
adzalandira chilango (china)
Chowawa kwambiri, (pa tsiku
lachiweruzo)
16. Fanizo la achinyengo
(Amunafikuna Pakuwanyenga
Banu Nadhiri kuti Amupandukire
Mneneri wa Mulungu) Lili ngati
satana (ponyenga munthu Kusiya
chikhulupiriro). Adati kwa lye:
"Mkane (Mulungu)." Ndipo
pamene Adamkana, (satana) adati:
"Ine sindili Ndi iwe; ndithu, ine
Siirat 59. AI-Hashr Juzu 28
1202
YA*>!
o H jJiJ-l 0jj-»»
ndikuopa Mulungu, Mbuye wa
zolengedwa."
17. Choncho mapeto a onse
awiriwo, Kudali kukalowa ku
moto ndi kukhala M'menemo
muyaya. Iyi ndiyo Mphoto ya
anthu onyenga (ochenjerera
Anzawo).
18. E, inu amene
mwakhulupirira! Muopeni
Mulungu (potsatira malamulo Ake
ndi Kusiya zimene waletsa) ndipo
alingalire Munthu aliyense
zamawa zimene Watsogoza
muopeni Mulungu ndithu
Mulungu, Ngodziwa zimene
mukuchita (Ndipo adzakulipirani
pa zimenezo).
19. Musakhale, (inu
okhulupirira) monga Amene
aiwala zoyenera kuchitira
Mulungu; (naye Mulungu)
wawaiwalitsa Mitima yawo
(powachotsera kuzindikira Zimene
zingawathandize). Amene wa
Ndiwo olakwa kwakukulu (otuluka
Ku chilamulo cha Mulungu).
20. Sangafanane anthu a ku
moto, (Olangidwa), ndi anthu a ku
Jannah, (Opeza mtendere). Anthu
aku Jannah Ndiwo opambana.
21. Chikhalakuti
tidaivumbulutsa Qur'an iyi
Pamwamba pa phiri, ukadaliona
Surat 59. Al-Hashr Juzu 28 I 1203 1 T A *>»
OS j£±-\ Ojj--
phirilo Lili lodzichepetsa ndi
kung'ambika Chifukwa choopa
Mulungu. Awa ndi Mafanizo
omwe tikuwapereka kwa anthu
Kuti aganizire.
22. lye ndi Mulungu, Amene
palibenso Wina wopembedzedwa
mwachoonadi Koma lye, Wodziwa
zamseri ndi Zooneka. lye
Ngwachifundo chambiri Ndiponso
Ngwachisoni.
23. lye ndi Mulungu, Amene
palibenso Wina wopembedzedwa
mwachoonadi Koma lye, Mwini
chilichonse, Woyera, Mwini
mtendere, wotsimikizira (aneneri
Ake mphamvu yochitira
zozizwitswa,) Msungi wa
chilichonse (yemwe akuona
Zochita za akapolo Ake;)
Wamphamvu Zopambana,
Mgonjetsi Wotukuka Muulemerero;
Wamkulukulu.Wapatukana (dzina
Mulungu kuzimene
Akumuphatikiza nazo.
24. lye ndi Mulungu; Mlengi
wa (zinthu, Palibe chomfanizira);
Muumbi wa Chilichonse. Mkonzi
wa maonekedwe A zinthu, Ake ndi
maina abwino, zonse Za kumwamba
ndi pansi Zikumlemekeza lye ndi
kumyeretsa Kumakhalidwe
osayenerana ndi Ulemerero
Wake.Iye wopambana Ndiponso
Wanzeru zakuya.
Surat 60. Al-Mumtabanah Juzu 28
1204
Y A tji-1 *\ ♦ &?CLtS\ 3jJ-»
Surayi yayamba ndi kuwaletsa Asilamu kugwirizana ndi
Amshirikina, amene ndi adani a Mulungu ndiponso adani awo
pachifukwa cha kumkana Mulungu ndi kumsamutsa Mthenga
wa Chauta mu mzinda wa Makka. Ndipo surayi yaloza chidani
chimene chili m'mitima mwawo pa Asilamu chofuna
kuwamaliza onse ngati angathe kutero.
Yalongosolanso chitsanzo chabwino cha Ibrahim ndi amene
adali nawo pamodzi, pakupatukana kwawo ndi Amushirikina
ndi zimene amazipembedza kusiya Mulungu. Ndipo adalengeza
chidanicho ndi iwo pokhapokha atamkhulupirira Mulungu
mmodzi.
Yalongosolanso za amene Asilamu angathe kugwirizana
nawo mwa anthu azipembedzo zina ndi kukhalirana nawo
mwamtendere; ndi amene nkosayenera kugwirizana nawo. Kwa
amene sakutiputa ndipo sakuthandiza adani athu potichitira
mtopola, tichite nawo chilungamo ndi kukhala nawo
mwaubwino. Koma amene akutimenya pa chipembedzo ndi
kuthandiza adani kutitulutsa m'nyumba zathu, iwo wo ndiomwe
Chauta watiletsa kugwirizana nawo ndi kuwachitira zabwino.
Kenaka yalongosola malamulo kwa Asilamu achikazi omwe
asamukira ku Chisilamu ndi kusiya amuna awo Amushirikina.
Ndiponso malamulo kwa akazi aopembedza mafano amene
asamuka kusiya amuna awo Achisilamu kudziko la Shiriki
(lopembedza mafano). Ndipo yatsatizanso kulongosola za
lonjezo la akazi amene amalowa Chisilamu pazimene
amamlonjeza Mneneri wa Mulungu (madalitso ndi mtendere
zikhale naye).
Surayi yamaliza ndi kuletsa kugwirizana ndi adani amene
Mulungu wawakwiira.
Surat 60. Al-Mumtahanah Juzu 28
1205 ™ *><
*l ♦ <U^cull dja-j
Surat Al-Mumtahanah LX
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. E, inu amene
mwakhulupirira! Musawachite
adani Anga Ndi adani anu kukhala
athandizi anu ndi Kumawauza
(nkhani zanu) mwa chikondi,
Pomwe iwo sanakhulupirire
choonadi Chimene chakudzerani.
Mneneri Wake, Adamtulutsa
Mtumiki ndi inu nomwe
(M'nyumba zanu) chifukwa
chakuti Mumakhulupirira
Mulungu, Mbuye wanu, (Palibe
cholakwa chilichonse chimene
Mudawachitira,) ngati mwatuluka
Kukachita Jihad pa njira Yanga ndi
Kufunafuna chikondi Changa;
(musapalane Nawo ubwenzi)
mukuwatumizira chinsinsi. (Chanu
cha nkhondo) chifukwa cha
Chikondi (chanu ndi iwo);
(Musachitenso zimenezi) pomwe
Ine Ndikudziwa zimene inu
mukubisa ndi Zimenene
mukuzisonyeza (poyera); Amene
akuchita zimenezi mwa inu, Ndiye
kuti wataya njira yoongoka. 1
O^ly^ll^
1 Inu Asilamu amene mwakhulupirira mwa Mulungu ndi Mthenga Wake(SAW)
musawachite makafiri amene ndi adani anga ndiponso adani anu kukhala
okondedwa anu ndi abwenzi anu. Chisonyezo cha chikhulupiriro kwa Msilamu
ndiko kuwada adani a Mulungu, osati kuwakonda ndi kupalana nawo ubwenzi.
Su rat 60. Al-Mumtahanah Juzu 28 1 206 TA ^jA-i
"V • <U?i£felt djj~*>
2. Akakumana nanu
(pankhondo) akukhala Adani anu
ndipo akukutambasulirani Manja
ndi malirime awo moipa
(Pokumenyani ndi
kukutukwanani); ndipo
Akulakalaka mukadakhala
Osakhulupirira (kuti mufanane
nawo).
3. Abale anu ngakhale ana anu
Sadzakuthandizani tsiku la Kiyama
(Mulungu) adzaweruza (pakati
panu), Ndipo Mulungu akuona
Zimene mukuchita.
4. Ndithu, inu muli ndi
chitsanzo chabwino Cha (mtumiki)
Ibrahima ndi amene Adali naye
pamene adawauza anzawo
(Osakhulupirira kuti): "Ndithu, ife
Tapatukana nanu pamodzi ndi
milungu Yanu imene
mukuipembedza kusiya Mulungu;
takukanani, ndipo chidani ndi
Kusakondana zaonekera poyera
pakati Pa inu ndi ife mpaka
muyaya, kufikira, Mutakhulupirira
mwa Mulungu mmodzi (Inunso
chitani chimodzimodzi, muwakane
Abale anu amene ali akafiri),
kupatula Mawu a Ibrahima pamene
adamuuza tate Wake (kuti):
"Ndithu, ndikupempherani
Chikhululuko. Palibe chimene
Ndingakutetezereni nacho kwa
Mulungu (Ngati mutamuphatikiza
mm
^&^mmm
Surat 60. Al-Mumtahanah Juzu 28
1207 TA*>1
1 ♦ 4^cull
°J>"
Mulungu ndi zina". Mawu
amenewo musatsatire koma
Pempherani motere:) "O, Mbuye
wathu! Kwa Inu tatsamira. Ndipo
kwa Inu Tatembenukira ndiponso
Kobwerera nkwa inu." 1
5. O, Ambuye athu! Musatichite
kukhala Mayeso kwa amene
sadakhulupirire, Tikhululukireni
Mbuye wathu! Ndithu Inu, Ndinu
Amphamvu zopambana Ndiponso
Anzeru zakuya.
6. Ndithu muli nacho inu kwa
iwo (Ibrahima Ndi omsatira)
chisanzo chabwino kwa Amene
akuyembekezera kukumana ndi
Mulungu ndi tsiku lomaliza. Ndipo
Amene anyozere ndithu, Mulungu
Ngolemera (ndipo)
Ngotamandidwa.
7. Mwina Mulungu angaike
chikondi Pakati panu ndi ena mwa
amene Mumawada (poiongolera
mitima yawo Kukhulupirira mwa
Mulungu), Mulungu Ngokhoza
chilichonse Ndiponso Mulungu
Ngokhululuka; Ngwachisoni.
8. Mulungu sakukuletsani
kuwachitira Zabwino ndi
&?•"■'-"
a^%&\^\^^
1 Apa akutiuza kuti titsanzire zimene adachita tate wa Shariya amene ndi
Ibrahima pamodzi ndi omtsatira ake pamene adadzipatula kwa makolo awo
ndi abale awo omwe adali m'chipembedzo chonama.Msilamu amkonde
Mulungu kuposa tate wake, ana ake, mkazi wake, chuma chake ndi thupi lake
limene. Atsogoze zofuna za Mulungu asanachite china chilichonse. Akatero
akhala kuti wakhulupirira Mulungu mwachoonadi.
Surat 60. Al-Mumtahanah Juzu 28
1208
YAc>»
1, * 4a * &»ll 3jJ-*»
chilungamo amene
Sadakumenyeni ndi kukutulutsani
M'nyumba zanu chifukwa cha
Chipembedzo.Ndithu, Mulungu
Akukonda Achilungamo. 1
9. Mulungu akukuletsani
kugwirizana Nawo amene
adakumenyani chifukwa Cha
chipembedzo ndi kukutulutsani
M'nyumba zanu, ndi amene
adathandiza Kukutulutsani. Amene
ati agwirizane Nawo Iwowo ndiwo
Achinyengo.
10. E, inu amene
mwakhulupirira! Akakudzerani
Asilamu achikazi Osamuka,
ayeseni mayeso (kuti Mudziwe
chikhulupiriro chawo); Mulungu
ali wodziwa kwambiri za
Chikhulupiriro chawo; ngati
Mutawadziwa kuti ndiokhulupirira
Musawabwezere kwa
osakhulupirira. Akaziwo saloledwa
kukwatiwa ndi Osakhulupirira,
iwonso saloledwa Kuwakwatira.
Abwezereni chiwongo Chimene
adapereka amuna
Osakhulupirirawo. Ndipo palibe
tchimo Kwa inu kuwakwatira,
(ngakhale adasiya Amuna awo
achikafiri (ku Makka) Ngati
muwapatsa chiwongo chawo.
9> >l'Z 9 '\ 9 t\' 'vrHfiZj'i' >ll
»&4'
* %
©
1 Mulungu sakutiletsa kuwachitira zabwino anthu amene sali Asilamu, mmalo
mwake akutilamula kuti tiwachitire zabwino ngati alibe upandu uliwonse ndi
Asilamu.
Surat 60. Al-Mumtahanah Juzu 28
1209 TA*>i
*\ • 4,'^cull 5jJ-»»
Musakangamire maukwati ndi
akazi Achikafiri (osakhulupirira
amene Adatsalira ku Makka).
Itanitsani Zimene mudapereka kwa
akazi anu (Achikafiriwo), naonso
Akafiri aitanitse Zimene adapereka
(kwa akazi awo Akalowa
m'Chisilamu). Limeneli ndi
Lamulo la Mulungu limene
Akulamula pakati panu. Mulungu
Ndiwodziwa kwambiri ndiponso
Ngwanzeru poika malamulo.
11. Ndipo ngati mmodzi mwa
akazi anu Atakuthawani kupita
kwa Akafiri, Ndipo
(mwadzidzidzi) mwakachita
Nkhondo (ndi kupeza chuma
chosiya Adani anu), apatseni
amene awathawa Akazi awo
chofanana ndi chimene Adapereka
(pokwatira). Ndipo Muopeni
Mulungu amene inu
mukumkhulupirira.
12. E, iwe Mtumiki!
Akakudzera akazi Okhulupirira
kudzakulonjeza kuti Samphatikiza
Mulungu ndi chilichonse Ndi kuti
saziba,sazichita chiwerewere,
Sazipha ana awo ndi kuti sazinena
Bodza lamkunkhuniza, lomwe
akulipeka Pakati pa manja awo ndi
miyendo yawo (Pompachika
mwana kwa wina amene Sali tate
wake), ndi kutinso Sadzakunyoza
pachinthu chabwino (Chimene
&''JA1
Surat 60. AI-Mumtahanah Juzu 28
1210
tA *>i
*\ ♦ <U*tioil Oj^mi
ukuwaitanira), landira Lonjezo
lawolo, ndipo apemphere
Chikhululuko kwa Mulungu.
Ndithu Mulungu
NgokhululukaKwambiri,
Ngwachisoni.
13. E, inu amene
mwakhulupirira! Musagwirizane
ndi anthu amene Mulungu
wawakwiyira ndipo ataya Mtima
wopeza mphoto tsiku lomaliza
(Chifukwa cha machimo awo
ochuluka) Monga momwe atayira
mtima akafiri Za kuuka kwa
amene ali m'manda.
Surat 61. As-Saff Juzu 28
1211
Ut>t
*\ \ uuaJl 5jj^
Surayi yayamba ndi kufotokoza kuti zakumwamba ndi za
m'dziko lapansi zikulemekeza Mulungu ndi kumyeretsa ku
Makhalidwe osayenerana ndi ulemerero Wake. Ndipo yapitiriza
kunena kuti nkosayenera kwa okhulupirira kuyankhula zimene
sakuchita ndi kuti Chauta amakonda kuti iwo azikhala dzanja
limodzi kwa adani awo. Kenako yafotokoza za kupandukira
choonadi kwa ana a israeli kupyolera mmalireme a Mithenga
iwiri yolemekezeka: Musa ndi Isa, ndi kuti iwo amayesetsa
kuzimitsa kuunika kwa Mulungu, koma Chauta amakwaniritsa
kuunika Kwake.
M' surayi muli lonjezo la Mulungu lakuti atukula
chipembedzo Chake cha Chisilamu kuti chikhale pamwamba pa
zipembedzo zina ngakhale anthu ophatikiza Chauta ndi mafano
chikuwaipira chipembedzochi.
Pomalizira surayi yalimbikitsa Asilamu kuchita (Jihad)
panjira ya Mulungu pochita ndi chuma ndi matupi awo. Ndipo
ochita (Jihad) yawalonjeza kuti adzakhululukidwa machimo
awo ndi kukalowa ku Jannah. Okhulupirira yawalimbikitsanso
kuti akhale athangati pa chipembedzo cha Mulungu monga
momwe adalili ophunzira a Isa mwana wa Mariam. Ndipo
Chauta adzalimbikitsa okhulupirira ndi chithandizo Chake lye
Ngopambana chilichonse, Mwini nzeru zokwanira.
Surat 61. As-Saff Juzu 28
1212 *A*>i
1 1 Jl*}\ Ijf*
Surat As-SaffLXI
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Zonse zakumwamba ndi
zapansi Zimalemekeza Mulungu
(ndi Kumyeretsa kumakhalidwe
osayenera Ndi ulemerero Wake).
Ndipo lye yekha Ngopambana pa
chilichonse; Wanzeru Zakuya.
2. E, inu amene
mwakhulupirira! Bwanji
mukunena Zimene simuchita? 1
3. Mulungu amakuda Zedi
kunena zinthu Zimene simuchita.
4. Ndithu, Mulungu akukonda
amene Akumenya nkhondo Panjira
Yake (yofalitsa Chipembedzo
Chake), ali pamzere (Umodzi) uku
ali monga chomanga, Chomangika
mwamphamvu. 2
5. Ndipo (kumbuka iwe
Mneneri{SAW}) Pamene Musa
adanena kwa anthu ake kuti:
"Ndichifukwa ninji
mukundivutitsa ine mukudziwa
v*.
■
Q^JHt^jll^
■&
osssa
uSSS^SsWfi
©<
(Ndime 2-3) Khalidwe la munthu limene limakwiyitsa Mulungu kwambiri
ndiko kunena zokoma chikhalirecho zochita zili zoipa. Amawanyenga anthu
ndi mawu otsekemera koma zochita zake ndizachinyengo zokhazokha.
Munthu wa makhalidwe otere, malipiro ake ndi kulowa ku nthukutira yamoto.
Choncho zochita zanu zifanane ndi zimene mukuyankhula. Apeweni
makhalidwe achiphamaso.
2 Mulungu akufuna kuti Asilamu akhale dzanja limodzi pofalitsa Chisilamu,
agwire ntchito yokomera gulu lonse mothangatana.
Surat 61. As-Saff Juzu 28
1213
ta ^jA-i
*V ^ uLaJi «jj-»
kuti ine ndine Mtumiki wa
Mulungu kwa inu?" Ndipo pamene
Adapitiriza kupandukira choonadi,
Mulungu adaipinda mitima Yawo
(kuti isalandire chiongoko);
Mulungu saongola anthu otuluka
M'chilamulo Chake.
6. Ndiponso (kumbuka) pamene
adanena (Mtumiki) Isa mwana wa
Mariam, Kuti: "E inu ana a
Israeli INdithu ine Ndine Mtumiki
wa Mulungu kwa inu, Amene
ndikuchitira umboni zimene
Zidadza patsogolo panga za buku
la Chipangano chakale (Torah)
ndipo Ndikuuzani nkhani yabwino
ya mthenga Amene adzadze
pambuyo panga, dzina lake
Ahamad (Muhammad{SAW})'\
Koma Pamene adawadzera
(Mtumiki Wolonjedzedwayo) ndi
zisonyezo Zowonekera poyera
(kuti iye ndi Mtumiki wa
Mulungu). Adati: "AwaNdi
matsenga owonekera".
7. Kodi ndani oipitsitsa kuposa
yemwe Wapekera Mulungu bodza,
pomwe iye Akuitanidwira ku
Chisilamu (Chipembedzo choona
ndi chabwino)? Ndipo Mulungu
saongola anthu Achinyengo.
8. Akufuna kuti azimitse
dangalira la Mulungu ndi
pakamwa pawo ndipo Mulungu
Ngokwaniritsa dangalira Lake
®&J\2$\
>'t* f "i\i \>>' \*t'>' 1\'$A
'9
Surat 61. As-Saff Juzu 28
1214
TA «.j*-»
*\ ) uLaJl Qjy
Ngakhale ziwaipire
osakhulupirira. 1
9. lye ndi amene adatuma
Mtumiki Wake
(Muhammad{SAW}) ndi
chiongoko Ndi chipembedzo
choona, kuti achiike Pamwamba
pa zipembedzo zonse, Ngakhala
kuti ophatikiza Mulungu ndi
Mafano zikuwaipira.
10. E, inu amene
mwakhulupirira! Kodi
Ndikudziwitseni malonda amene
Angakupulumutseni ku chilango
Chowawa?
11. Muzimkhulupirira Mulungu
ndi Mtumiki Wake; ndipo
muzichita Jihad pa njira ya
Mulungu ndi chuma chanu, ndi
matupi Anu. Zimenezo nzabwino
kwa inu Ngati muli odziwa.
12. Akukhululukirani machimo
anu ndipo Akulowetsani m'minda
momwe Mitsinje ikuyenda pansi
pake, ndiponso (Adzakupatsani)
mokhala mwabwino Ku minda
yamuyaya. Kumeneko ndiko
Kupambana kwakukulu.
13. Ndizina zomwe
mukuzifuna. Thandizo (Lonse)
lichokera kwa Mulungu ndi
*>
'4 i
1 (Ndime 8-9) Mulungu akulonjeza kuti Chisilamu chidzapambana zipembedzo
zonse ngakhale osakhulupirira akuchithira nkhondo.
Surat 61. As-Saff Juzu 28
1215 tA*>»
*\ \ Juph\ djj-*i
Kugonjetsa kumene kuli pafupi;
ndipo Auze nkhani yabwino
Okhulupirira,
14. E, inu amene
mwakhulupirira! Khalani
Othangata kufalitsa chipembedzo
cha Mulungu (pamene Mtumiki
akukuitanani Kuti mumthangate)
monga momwe Adanenera Isa
mwana wa Mariam Powauza
otsatira ake: "Ndani
Adzandithangata pa ntchito ya
Mulungu (Yofalitsa chipembedzo
Chake)? Otsatira ake adanena: "Ife
ndife Othangata (kufalitsa
chipembedzo cha)
Mulungu."Choncho gulu Una la
ana a Israeli lidakhululupirira,
ndipo gulu Lina
silidakhululupirire, tero
Tidawapatsa mphamvu amene
Adakhulupirira pa adani awo,
ndipo Adali opambana.
"if" -V T J> i5'-'r , " l ^fTli , " , f!'
9 "L'S* ""i
Surat 62. Al-Jumu'ah Juzu 28
1216
YA*>»
*\ Y 4Jt*i*l djj-a
SURAT AL-JUMU'AH LXII
Surayi yayamba ndi kufotokoza kuti zonse za kumwamba ndi
zapansi zikulemekeza Mulungu ndi kumpatula ku makhalidwe
osayenerana ndi ulemerero Wake. Ndipo kenaka yatchula
mtendere umene Chauta adaupereka kwa Aarabu amene
samadziwa kulemba ndi kuwerenga powatumizira Mneneri
wochokera mwa iwo kuti awaphunzitse nzeru ndi kuwayeretsa.
Ndithu, chimenechi ndichisomo cha Mulungu chomwe
amachipereka kwa amene wamfuna.
Kenako surayi yadzudzula Ayuda chifukwa cha kusiya
kutsatira malamulo omwe adali m'chipangano chakale. Ndipo
yatsutsa bodza lawo loti iwo okha ndiwo okondedwa ndi
Chauta, osati mitundu ina. Ndiponso yawabetchera kuti ngati
akunena zoona ailakelake imfa kuti akakumane ndi
wokondedwa wawoyo. Koma sangathe kutero chifukwa cha
machimo awo amene adawachita.
Kenako yamaliza ndi kulamula Asilamu kuti achite changu
kukapemphera swala ya jumu'a akamva kuitana; ndi kuti asiye
malonda, ndipo swala ikatha, abalalikane padziko kunka
nafunafuna zabwino za Mulungu. Ndiponso yawalangiza kuti
malonda ndi masewero zisawachititse kukhala otanganidwa
nazo ndi kusiya kumvera ulaliki wa tsiku limenelo.
Surat 62. Al-Jumu'ah Juzu 28
1217
YA frjJUl
% Y AjtJrl 3jj-»
Sural Al-Jumu'ah LXI1
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Zonse zakumwamba ndi
dziko lapansi Zikulemekeza
Mulungu; Mfumu Woyera,
Wamphamvu zopambana ndi
nzeru Zakuya (ndi kumyeretsa ku
makhalidwe Osayenerana ndi
ulemerero Wake).
2. lye ndiAmene adatumiza kwa
Ummiyyina (Osadziwa kulemba
ndi kuwerenga), Mtumiki
wochokera mwa iwo kuti
Awawerengere ndime Zake ndi
kuti Awayeretse (ku uchimo ndi
Kumakhalidwe oipa) ndi
kuwaphunzitsa Qur'an ndi mawu
anzeru (Amtumiki) ndithu kale
adali Osokera kowonekera
(Mtumiki {SAW} Asadadze kwa
iwo). 1
o^l^JMU-
1 Arabu amatchedwa "Ummiyyuna" chifukwa chakuti samadziwa kulemba ndi
kuwerenga. Kusadziwa kulemba ndi kuwerenga kudafala pakati pawo ndipo
ngakhale Mtumiki amene samadziwa kulemba ndi kuwerenga chilichonse.
M'ndime imeneyi, Mulungu akutiphunzitsa kuti adampereka Muhammad
(madalitso ndi mtendere zikhale naye) kuti awaongolere anthu kunjira
yoongoka. lyeyu adaperekedwa panyengo imene anthu adali ndi khumbo la
Mneneri wa Mulungu kuti watsogolere ku njira yolungama pakuti pa nthawiyo
zipembedzo zonse za Mulungu zidali zitaonongeka. Pachiyambi Arabu
amatsatira chipembedzo cha Ibrahim. Kenako adasintha nkuyamba
kupembedza mafano. Adayambitsa zinthu zambiri zosalolezedwa ndi Chauta.
Ndipo nawonso anthu amabuku, Ayuda ndi Akhrisitu, adasintha zophunzitsa
za mabuku awo. Choncho Mulungu adapereka Muhammad(SAW) ndi
malamulo aakulu okwanira bwino. Mkati mwake mudali chilichonse chofunika
Surat 62. Al-Jumu'ah Juzu 28
1218
YA*jA-l
*\ V AjuJrl Ojj-*»
3. Ndipo (adamtumizanso) kwa
ena Mwa iwo, omwe sadakumane
nawo, Ndipo lye (Mulungu)
Ngopambana (Pa chinthu
chilichonse ndi Wamphamvu
Zoposa ndiponso) Wanzeru zakuya.
4. Umenewo ndiwo ubwino wa
Mulungu akuupereka kwa amene
Wamfuna (mwa akapolo Ake);
ndipo Mulungu yekha ndi Mwini
Ubwino waukulu.
5. Fanizo la (Ayuda) amene
Adawasenzetsa Taurat
(chipangano Chakale,
pokakamizidwa kuti atsatire
Zophunzitsa za bukulo, koma
Osatsatira), ali ngati Bulu amene
Akusenza mabuku akuluakulu
anzeru, (Koma osathandizidwa
nawo). Taonani kuipa fanizo la
anthu amene Atsutsa zisonyezo za
Mulungu. Ndipo Mulungu
saongola anthu achinyengo. 1
6. Nena: "E, inu Ayuda! Ngati
Mwadziganizira kuti ndithu, ndinu
Okondedwa a Mulungu kuposa
(Mitundu ina ya) anthu, ilakelakeni
Imfa (kuti mukalowe ku mtendere
wa Mulungu) ngati mukunena zoona.
ws^ffm^m
m'moyo wa anthu pa nyengo zosiyanasiyana pa moyo wa padziko ndi wa pa
tsiku lomaliza. Mulungu adampatsa zabwino zomwe sadampatseponso wina
aliyense, woyamba ndi womaliza.
1 Mulungu Wotukuka, akufanizira Ayuda amene amadziwa kuwerenga Taurat
bwinobwino, koma zomwe akuwerengazo osazigwiritsa ntchito, ngati bulu
wosenza mabuku akuluakulu popanda chopeza pomwe mabukuwo ali odzaza
ndi zinthu zabwino zophunzitsa nzeru zabwino.
Surat 62. Al-Jumu'ah Juzu 28
1219
TA*j*-l
*\ t AjuJrl Ojj-»
\ ^.'i-l'&dLjKjif
l<oj>yy
%$2ftZiP$
7. Ndipo sangailakelake
Mpang'ono pomwe chifukwa cha
(zoipa) Zimene manja awo
atsogoza! Ndipo Mulungu
akudziwa bwino za (anthu)
Osalungama.
8. Nena (kuti): "Ndithu, imfa
imene Mukuithawa (palibe
chipeneko) Ikumana nanu; kenako
muzabwezedwa Kwa Wodziwa
zobisika ndi zooneka; Ndipo
adzakuuzani zimene mudali Kuchita.
9. E, inu amene
mwakhulupirira! Kukaitanidwa
kuswala (mapemphero) Tsiku la
Ijumaa, pitani Mwachangu
kukamtamanda Mulungu, Ndipo
siyani malonda; zimenezo
(Mwalamulidwazo) mzabwino
kwa Inu ngati mukudziwa. 1
10. Tsono Swala ikatha,
balalikanani padziko, Ndipo funani
ubwino wa Mulungu; Ndipo
mtamandeni Mulungu (ndi mitima
Yanu, ndi malirime anu) kwambiri
Kuti mupambane (padziko lapansi
Ndi pa tsiku lomaliza).
1 M'ndime imeneyi akutiphunzitsa kuti tikamva adhana (kuitana) tsiku la ljuma,
tisiye chilichonse chimene tikuchita ndi kupita mwachangu kukapemphera
pemphero la ljuma. Pempheroli ndilofunika kwa Msilamu aliyense makamaka
amuna.
Asilamu amasonkhana m'Misikiti ikuluikulu pa tsiku limeneli pa sabata
iliyonse. Ndipo pa tsiku limeneli ndipomwe Mulungu adakwaniritsa zolenga
zake zonse. Adamu adalengedwa pa tsikuli ndipo adalowetsedwa ku Jannah
tsiku lomweli. Ndipo adatulutsidwa m'menemo pa tsiku la ljuma. Mtumiki
adafotokozanso za kuti Kiyama idzadza tsiku la ljuma.
©&
'.>?[:£'<
Surat 62. Al-Jumu'ah Juzu 28 1220 * * *>'
1 1 4*uJH 5jj--
11. Ndipo akaona malonda
kapena Masewero, akubalalika
kunka ku Zimenezo ndi kukusiya
uli chiimire (Ukuchita khutuba ndi
anthu ochepa). Nena (kwa iwo):
"Zimene zili kwa Mulungu
nzabwino kwa inu kuposa
Masewero ndi malonda. Ndipo
Mulungu Ngwabwino kwambiri
kuposa Opatsa onse.
Surat 63. AI-Munafiqun Juzu 28 1 1221 I *A *>! n r *f*M ^
Surayi yasonkhanitsa makhalidwe a anthu achinyengo ndi
kufotokoza za iwo kuti amaonetsera poyera chikhulupiriro
chawo ndi malirime awo abodza. Ndipo yalongosola kuti iwo
akuchiyesa chikhulupiriro chawo chonama kukhala chishango
chawo chodzitchinjiriza nacho kuti asatchedwe kuti ndi akafiri
(osakhulupirira). Kenaka yalongosolanso kuti iwo ndi eni
matupi okongola; osalala kwa yemwe wawaona. Ndipo zonena
zawo nzomveka bwino kwa yemwe wazimva. Koma ngakhale
ali tero, iwo m'mitima mwawo mulibe chikhulupiriro ngakhale
pang'ono. Ali ngati chikuni chimene chasamizidwa; mulibe
moyo mwa iwo, wauzimu.
Surayi yafotokozanso za iwo kuti amadzikweza Mtumiki
akawaitana kuti awapemphere chikhululuko. Kenako yatsutsa
bodza limene anthu achinyengo amanena kuti iwo
ngolemekezeka ndipo Asilamu ngonyozeka. Ndipo pomaliza
yalimbikitsa Asilamu kuti apereke chuma chawo panjira ya
Mulungu mwachangu imfa isadampeze mmodzi wa iwo kuti
asadandaule ndi kulakalaka kuti ndibwino akadaonjezeredwa
nthawi ya moyo wake. Koma Mulungu sangauchedwetse mzimu
nthawi ya imfa yake ikafika.
Surat 63. Al-Munafiqun Juzu 28 1222 * A *>'
■vro^uii Sjj--
Surat Al-Munafiqun LXIII
"fc;^; $ȣ ;;Sp
,, __ r^v—
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Akakudzera achinyengo
akunena kuti: "Tikuikira umboni
kuti iwe ndiwe Mtumiki wa
Mulungu ndipo Mulungu
Akudziwa kuti iwe ndiwe mtumiki
Wake." Ndipo Mulungu akuikira
Umboni kuti achinyengo ngabodza
(Pa zomwe akunena).
2. Kulumbira kwawo (kwa
bodza) Akuchita kukhala
Chotetezera (chuma chawo Ndi
matupi awo). Ndipo atsekereza
(Anthu kuyenda) panjira ya
Mulungu Ndithu nzoipa zedi
zimene amachita.
3. Zimenezo nchifukwa chakuti
Iwo Adakhulupirira
(modzionetsera), Kenako adakana
(mobisa). Choncho Mitima yawo
idatsekedwa kotero kuti Iwo
sangathe kuzindikira (chimene
Chingawapulumutse Ku chilango
cha Mulungu.)
4. Ndipo ukawaona,
akukondweretsa Matupi awo;
ndipo akayankhula Umvetsera
zoyankhula zawo (Chifiikwa
chakuthwa kwa malirime Awo,
pomwe mkati mwawo Nding'oma
o^l<^3ll*iU.
^^^m^^
a
bi>
Surat 63. Al-Munafiqun Juzu 28
1223
YA*>!
nr o^duii 5jj**»
yopanda kanthu); iwo ali Ngati
matsinde a mitengo yomwe
Yayadzamiritsidwa ku chipupa;
(mwa Iwo mulibe moyo).Mkuwe
uliwonse (Umene akuumva)
akuganiza kuti Ukulinga
iwo,(chifiikwa cha Kuzindikira
chinyengo chawo); iwowa Ndi
adani; chenjerani nawo. Mulungu
Awatemberere!Mwanjira yanji
Akuchotsedwa (kuchoonadi)!
5. Kukanenedwa kwa iwo kuti:
"Bwerani, Akupemphereni
chikhululuko mthenga Wa
Mulungu, akutembenuza mitu
yawo (Monyoza ndi
modzitukumula), ndipo Uwaona
akunyoza uku akudzikweza
(Osasatira langizo).
6. Kwa iwowa nchimodzimodzi
Kuwapemphera kwako
chikhuluko, Kapena
kusawapemphera. Mulungu
sangawakhululukire (Chifukwa
cha kuzama kwawo
M'kusakhulupirira). Ndithu,
Mulungu Saongola anthu otuluka
m'chilamulo Chake.
7. Amenewa ndiwo omwe
akunena (kwa Ansari; (Asilamu
aku Madina, kuti): "Musawapatse
chuma (chanu) amene Ali ndi
Mtumiki wa Mulungu kuti
Abalalikane.'Tomwe nkhokwe
"*i?
Surat 63. Al-Munafiqun Juzu 28
1224
XA*>1
nr o^sLii 9jj~>
zonse (Zachuma) za kumwamba
ndi dziko Lapansi zili m'manja
mwa Mulungu (ndipo
amachipereka kwa Amene
wamfuna); koma achinyengo
Sakuzindikira (zimenezo). 1
8. Akunena kuti: "Ngati
tibwerera ku Madina
wolemekezeka adzatulutsa
Wonyozeka m'menemo. " Pomwe
Ulemerero ngwa Mulungu ndi
Mthenga Wake ndi okhulupirira;
koma Achinyengo sakudziwa
(Zimenezo).
9. E, inu amene
mwakhulupirira! Chuma Chanu
ngakhalenso ana anu
Zisakutangwanitseni ndi kusiya
Kukumbukira Mulungu (ndi
kukwaniritsaZimene
wakulamulani). Ndipo amene
Achite zimenezo iwo ndi otaika.
10. Perekani mwachangu
(panjira ya Mulungu) zina mwa
ofe 3<$&^%^&^j
1 (Ndime 7-8) Chifukwa chomwe ndime izi zidavumbulutsidwira ndi kuti tsiku
lina Mtumiki(SAW) pomwe adali ndi gulu lake la nkhondo, munthu wina wa
m'madera am'midzi adakangana ndi Msilamu wa mumzinda wa Madina
chifukwa cha madzi. Ndipo Mwarabu wa kumudzi uja adamenya Msilamu wa
m'Madina ndi thabwa. Poona izi Msilamu wa ku Madina adapita kukasuma kwa
mwana wa Ubayye amene adali Munafiki (wachinyengo). Ubayyeyo adamuuza
wosumayo kuti: "Musamawapatse chakudya omwe ali ndi Muhammad kuti
abalalikane, athawe njala ndi kumsiya yekha Muhammad(SAW)." Adatinso:
"Tikabwerera ku mzinda wa Madina, wolemekezeka adzatulutsa wonyozeka."
Apa amatanthauza kuti wolemekezeka ndiye iye, ndipo wonyozeka ndi
Mtumiki Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale naye). Ndipo Mulungu
adamuyankha ponena kuti: "Kulemekezeka ndi kwa Mulungu ndi Mthenga
wake ndi okhulupirira; koma anthu achinyengo sakudziwa zimenezi."
Surat 63. Al-Munafiqun Juzu 28 1225 I *A *>»
M" o^flduii Sjj--
zomwe Takupatsani, isanamfikire
mmodzi Wainu imfa
(mwadzidzidzi) ndi Kuyamba
kunena (modandaula), "Mbuye
wanga! Bwanji Osandichedwetsa
nthawi pang'ono Kuti
ndikhulupirire (ndi kuti Ndikonze
zina zimene Sindinazikwaniritse)
ndi kutinso Ndikhale mwa anthu
anu abwino."
11. Ndipo Mulungu
sauchedwetsa Mzimu (ngakhale
ndi mphindi Imodzi) ukaidzera
nthawi yake ya Imfa; ndipo
Mulungu Ngodziwa Zonse zimene
mukuchita, (ndipo Adzakulipirani
pa zimenezo).
Surat 64. At-Taghabun Juzu 28 1226 TA tjA-t M ^ifcli Sj^
Surayi yayamba ndi kufotokoza kuti zonse zakumwamba ndi
zam'dziko lapansi zikumpatula Mulungu ku zinthu zosayenera
ndi ulemerero Wake, ndi kuti lye ndi mwini ufumu ndiponso
Mwini kuyamikidwa. Ndi kutinso lye ali ndi mphamvu pa
chilichonse.
Kenako yasonyeza zisonyezo za kukwanira kwa nzeru Zake
ndi mphamvu Zake. Ndipo yafotokoza za amene adamkana kale
ndi kunyoza aneneri a Mbuye wawo, ndi m'mene adalawira
chilango pa machitidwe awo oipa.
Zimenezo nkuti aneneri awo amawadzera ndi zozizwitsa,
koma iwo adawatsutsa ndi kuwanyoza.
Kenako surayi yathetsa bodza la osakhulupirira m'kunena
kwawo kwakuti sadzauka ku imfa. Ndipo yawapempha anthu
kuti akhulupirire Mulungu pamodzi ndi Mtumiki Wake ndi
kuunika kumene kudavumbulutsidwa kwa iye. Ndiponso
yawachenjeza za tsiku lamsonkhano waukulu; tsiku limene
kudzaonekera poyera kulephera kwa anthu osakhulupirira.
Koma amene adakhulupirira ndi kumachita zabwino,
kupambana kwakukulu kudzakhala pa iwo. Ndipo
osakhulupirira adzakhala eni moto. Yafotokozanso kuti mavuto
amachitika kupyolera mchifuniro cha Chauta ndi kuti amene
akhulupirira Mulungu akuongola mtima wake.
Yawapemphanso anthu surayi kuti amvere Mulungu ndi
Mthenga Wake. Ndipo okhulupirira yawauza kuti chuma ndi ana
awo ndi mayeso. Asasiye chimene alamulidwa kuchichita
potanganidwa ndi chuma ndi ana. Ndipo yamaliza ndi kuwauza
kuti apereke chuma chawo panjira yabwino, ndi kuti Iye
Ngoyamika, Ngodekha, Ngodziwa zam'mseri ndi zoonekera
poyera. Adzawalipira pazimene akupereka pa njira Yake.
Iye Ngopambana ndipo sapambanidwa; Ngwanzeru ndipo
sachita zopanda pake.
Surat 64. At-Taghabun Juzu 28 I 1227 TA^i
n t jjuJi 5jj-a
Surat At-Taghabun LXIV
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Zonse zakumwamba ndi
zam'dziko Lapansi zikulemekeza
Mulungu (ndi Kumyeretsa ku
zinthu zosayenerana ndi
Ulemerero Wake; Ufumu Ngwake
ndipo Kutamandidwa kwabwino
Nkwake. Ndipo lye ali ndi
mphamvu pa chilichonse.
2. lye ndiAmene adakulengani
(Nonsenu popanda kuchokera ku
Chilichonse) choncho mwa inu
alipo Wosakhulupirira (Mulungu
wake) ndiponso Mwa inu alipo
wokhulupirira. Ndipo Mulungu
Ngopenya zonse zimene
Mukuchita (ndipo adzakulipirani
nazo).
3. Adalenga thambo ndi nthaka
Mwachoonadi ndipo
adakujambulani Majambulidwe
abwino; Ndipo Kobwerera nkwa
lye (pa tsiku Lachiweruziro).
4. (Mulungu) akudziwa
zakumwamba ndi Zam'dziko
lapansi, ndiponso akudziwa
Zimene mukuzibisa ndi zimene
Mukuzilengeza (zochita ndi
Zoyankhula); Mulungu Ngodziwa
Zam'zifuwa.
^ "^ : - - : ^ ==== ^Z_
oJ&3\^3\&\j
-^
©
ffri" *£'■
*<1t ' »< -c
9*A
®^daH
Surat 64. At-Taghabun Juzu 28 I 1228 I Y A t>
^ i ^ttsJt 5jj--
5. Kodi siidakufikeni nkhani ya
omwe Sadakhulupirire kale?
Adalawa (Zowawa) zazoipa za
zinthu zawo (Padziko lapansi).
Ndipo chilango Chowawa
chidzakhala pa iwo (tsiku Lomaliza).
6. Zimenezo nchifukwa chakuti
atumiki Awo amawadzera ndi
zozizwitsa koma Iwo amanena
(mwachipongwe) c Ha! Anthu
anzathu (onga ife) angationgole?'
Choncho sadakhulupirire (utumiki
Wawo) ndipo adanyoza (choonadi)
Potero Mulungu adawasiya (ndi
Kupanda chikhulupiriro kwawo)
ndipo Mulungu ngokwanira
ndiponso Ngoyamikidwa.
7. Amene sadakhulupirire
akumanama kuti Sadzaukitsidwa
ku imfa. Nena (kwa Iwo iwe
Mtumiki{SAW}): "Sizili choncho
Pali Mbuye wanga, ndithu
Mudzaukitsidwa ku imfa, ndipo
Mudzauzidwa zimene mumachita
(Padziko lapansi). Zimenezo kwa
Mulungu nzofewa nzosavuta
(kuzichita)"
8. Khulupirirani Mulungu ndi
Mtumiki Wake, ndi dangalira
limene Talivumbulutsa. Ndipo
Mulungu Ngodziwa kwambiri
zimene mukuchita.
9. (Kumbukirani) tsiku limene
Adzakusonkhanitsani chifukwa
^j^Maftss
Surat 64. At-Taghabun Juzu 28 | 1229 | Y A »>i % t ^udi 5^
cha Tsiku lakusonkhana
(zolengedwa Zonse), limenelo ndi
tsiku lolephera; Ndipo amene
akhulupirira mwa Mulungu ndi
kuchita zabwino, Anfafanizira
zoipa zake, ndipo Akamulowetsa
m'minda momwe Pansi pake
pakuyenda mitsinje; Adzakhala
m'menemo muyaya; Kumeneko
ndiko kupambana Kwakukulu. l
10. Koma amene
sadakhulupirire natsutsa
Zozizwitsa Zathu (zimene
Zidaperekedwa kwa Aneneri
Athu;) Iwowo ndi anthu akumoto;
adzakhala Mmenemo muyaya
amenewo Ndiwo mabwerero oipa.
11. Palibe vuto lililonse
lingapezeke Pokhapokha Mulungu
atafuna; ndipo Amene akhulupirira
Mulungu, (Mulungu) aongola
mtima wake (kuti Ukhale
wokhutira ndi chiweruzo cha
Mulungu). Ndipo Mulungu
Ngodziwa Chinthu chilichonse.
12. Choncho mverani Mulungu
ndipo Mverani Mtumiki ngati
munyozera, (Ndi zanu), ndithu
udindo wa Mtumiki Wathu
ndikufikitsa uthenga Omveka.
t>i
Tsiku lolephera: Akafiri adzakhala olephera chifukwa cha kusakhulupirira
kwawo. Nawonso Asilamu aulesi adzakhala olephera chifukwa cha
kusakwaniritsa kwawo malamulo a Mulungu.
Surat 64. At-Taghabun Juzu 28 I 1230 I * A *>»
1 i jjUsIi *jj-'
13. Mulungu, palibe wina
wopembedzedwa Mwachoonadi
koma lye. Ndipo kwa Mulungu
Yekha, okhulupirira atsamire.
14. E, inu amene
mwakhulupirira! Ndithu Ena mwa
akazi anu ndi ana anu Ndi adani
anu (chifukwa chakuti
Amakuchotsani kumbali yomvera
Mulungu pofuna kuti
mukwaniritse Zofuna zawo).
Chenjerani nawo. Ngati
Muwakhululukira ndi
kunyalanyaza Ndi kubisa zolakwa
zawo ndibwino Kwambiri, ndithu
Mulungu Ngokhululuka,
Ngwachisoni. 1
15. Ndithu, chuma chanu ndi
ana anu Ndimayeso (kwa inu);
koma kwa Mulungu kuli malipiro
aakulu (Kwa yemwe wasankha
kumvera Mulungu).
16. Choncho muopeni Mulungu
Mmene mungathere mverani
(Zophunzitsa Zake) ndipo tsatirani
(Malamulo Ake) komanso
perekani Zimene wakupatsani
$&fr&&$pm
1 (Ndime 14-15) Pakufunika kuti munthu akhale ndi muyeso wabwino. Chinthu
chilichonse achipatse choyenera chake. Nthawi zambiri kumapezeka kuti
munthu amalakwira Chauta chifukwa cha kufunitsitsa chuma, kapena
chifukwa chofuna kukondweretsa ana ake ndi mkazi wake ndi kunyalanyaza
malamulo a Mulungu. Choncho apa, chuma Chake, ana ake ndi mkazi wake
amasanduka adani ake okamuika m'mavuto kwa Mulungu. Nkofunika kwa
munthu kukondweretsa Mulungu ndi kumkonda asanakondweretse ndi
kukonda china chilichonse.
Surat 64. At-Taghabun Juzu 28
1231
YA^>l
*\ i ji\xS\ djj-*»
zikhala zabwino Kwa inu.
Dzichitireni nokha zabwino. Ndipo
amene watchinjirizidwa ku
Umbombo wake, iwowo ndiwo
Opambana.
17. Ngati mungamkongoze
Mulungu Ngongole yabwino
aiwonjezera kwa inu (Malipiro
ake) ndipo akukhululukirani
(Zolakwa zanu.) Ndipo Mulungu
Ngolandira kuthokoza, Ngoleza.
18* Ngodziwa zobisika ndi
zoonekera; Ngwamphamvu
zopambana; Ngwanzeru Zakuya.
jWy8ca#&iui£<$i
%s&fcm&
y**j
©
jp&fi^fi^j^^
Surat 65. At-Talaq Juzu 28
1232
TA^>l
Id j^UaJl Ojj^
Surayi ikufotokoza ena mwamalamulo osiyanirana ukwati
kudzanso edda ndi mitundu yake ndi malamulo ake polongosola
kuti mkazi wa edda akhale panyumba pomwepo pomwe
wasudzulidwapo. Ndi kuti apatsidwe zofunika pa moyo wake,
monga chakudya ndi pogona.
Pakuti polongosola malamulo amenewa, monga momwe ilili
njira ya Qur'an pali lonjezo labwino kwa amene akutsatira
malamulo a Mulungu; ndi lonjezo la chilango kwa amene
akupyola malirewo. Kenako yaloza zotsatira za odzitukumula
posiya kutsatira malamulo a Chauta ndi Aneneri Ake. Ndipo
yatsiriza ndikuwalimbikitsa Asilamu zoopa Mulungu ndi
kukumbukira chisomo cha Chauta powatumizira Mneneri wake
amene akuwawerengera ndime za Mulungu kuti awatulutse
mumdima ndi kuwaika m'kuunika. Ndiponso yafotokoza
mphamvu Zake zazikulu polenga thambo zisanu ndi ziwiri ndi
nthakanso chimodzimodzi.
Surat 65. At-Talaq Juzu 28
1233
YA*>I
\0 JtAiail djj-
Surat At-Talaq LXV
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. E, iwe Mneneri(SAW) ngati
Mufuna kusudzula akazi ukwati,
Asudzuleni mnyengo yowerengera
Edda yawo (kuwerengera edda
Kumayambika mkazi akakhala ndi
Twahara akachira matenda
akumwezi), Ndipo werengerani
nyengo ya edda. Ndipo Muopeni
Mulungu Mbuye wanu. Ndipo
Musawatulutse m'nyumba zawo
Ndiponso asatuluke kupatula
Akachita tchimo lalikulu loonekera
(Loyenera chilango, apo atha
Kutulutsidwa). Ndipo amenewa
ndiwo Malire a Mulungu (amene
Wawakhazikitsa kwa anthu Ake).
Ndipo Amene apyola malire a
Mulungu Wadzichitira yekha zoipa.
Sukudziwa (Cholinga cha malamulo
amenewa) Mwina Mulungu
adzadzetsa chinthu Pambuyo pake
(chosonyeza kuyanjana).
2. Ngati osiyidwawo nyengo
yawo (edda) Itayandikira kutha,
abwerereni mwa Ubwino kapena
asiyeni mwaubwino (Polekerera
nyengoyo kuti ithe); ndipo
(Powabwerera) funani mboni
ziwiri Zolungama zochokera mwa
inu (zimene Zichitire umboni kuti
^^^^saai
o&&\<jp$\&\j>.
Surat 65. At-Talaq Juzu 28
1234
tA^jJrl
n o JtAkJl 5j^
inu mukubwererana) Ndipo
perekani umboni chifukwa choopa
Mulungu. Zimenezo ndizo
akulangizidwa Nazo amene
akhulupirira mwa Mulungu Ndi
tsiku lomaliza.Ndipo amene
akumuopa Mulungu (potsatira
malamulo Ake), Amkonzera njira
yotulukira (m'mavuto).
3. Ndipo ampatsa riziki
kuchokera momwe
Samayembekezeramo. Ndipo
amene Akutsamira kwa Mulungu
(pa zinthu zake Zonse), ndiye kuti
Mulungu ali wokwana Kwa iye
(kumkonzera chilichonse), ndithu,
Mulungu Ngokwaniritsa cholinga
Chake ndi Chofuna Chake. Ndithu,
chinthu chilichonse Mulungu
wachipatsa mlingo wake
Woyenera (ndipo sichingaupyole).
4. Ndipo edda ya amene asiya
kudwala Kumwezi mwa akazi anu
chifukwa cha Kukula, ngati
mukukaika (nthawi Ya edda
yawo), edda yawo ndi miyezi Itatu.
Ndi omwe sadathe msinkhu edda
Yawo ndi momwemonso. Tsono
akazi Apakati nthawi yothera edda
yawo Ndipomwe abereka. Ndipo
amene aopa Mulungu amfewetsera
zinthu zake. (Kuti zikhale zosavuta.)
5. Limenelo ndilamulo la
Mulungu (Lomwe) walikhazikitsa
kwa inu. Ndipo amene aopa
Surat 65. At-Talaq Juzu 28
1235
TAf>l
10 (j^UaJl djj~>
Mulungu (Posunga malamulo ake),
Amam'fafanizira zoipa zake,
ndiponso Amamkulitsira malipiro
ake.
6. Akhazikeni (osiyidwawo)
m'mene Mukukhala inumo monga
momwe kulili Kupeza kwanu (ndi
mphamvu Zanu ngakhale kuti
mwawasiya ukwati). Musawavute
ndi cholinga chowapana (Kuti
athawe okha). Ngati ali ndi pakati,
Apatseni zonse zofunika pa moyo
Mpaka adzabereke. Ngati
akukuyamwitsirani ana anu
apatseni malipiro awo Mokwanira;
gwirizanani pakati panu
Mwaubwino ndi mofatsa. Ngati
wina Apereka mavuto kwa mnzake
(ndiye Kuti mwanayo)
adzamuyamwitsira (Mkazi) wina,
7. Wopeza bwino apereke
malinga ndi Kupeza bwino kwake;
ndipo amene Wachepekedwa riziki
lake, apereke (Kangachepe)
pazomwe Mulungu
Wampatsa. Mulungu sakakamiza
aliyense Kupatula zomwe ampatsa.
Mulungu apereka Kupeza bwino
pambuyo pa masautso.
8. Eni midzi yambiri adanyoza
lamulo La Mbuye wawo ndi
Aneneri Ake, Ndipo
tidawawerenga ndi chiwerengero
Chokhwima (posanthula zochita
zawo Zonse). Ndiponso
tidawalanga ndi Chilango chaukali.
o 1
Surat 65. At-Talaq Juzu 28 I 1236 I * A *>i
10 J^UaJl 5jj-»
9. Choncho adalawa kuipa kwa
zinthu Zawo ndipo mapeto azinthu
zawo adali Kutayika (kuonongeka
kwakukulu),
10. Mulungu wawakonzera iwo
chilango Chopweteka choncho,
muopeni Mulungu, Ee, inu eni
nzeru, amene mwakhulupirira,
Ndithu, Mulungu wavumbulutsa
Chikumbutso (Cholemekezeka
kwa inu).
11. Mtumiki (amene)
akukuwerengerani Ndime za
Mulungu zolongosola (Choonadi ndi
chonama) kuti Awatulutse
mumdima ndi kuwaika Ku dangalira
amene wakhulupirira ndi Kumachita
zabwino. Ndipo amene Akhulupirira
Mulungu ndi kumachita Zabwino,
adzamlowetsa m'minda Momwe
mitsinje ikuyenda pansi pake;
Akakhala m'menemo muyaya.
Ndithu Mulungu wamkonzera
riziki (dalitso) Labwino (Jannah) 1
12. Mulungu ndiYemwe
adalenga thambo Zisanu ndi ziwiri,
nthakanso Chimodzimodzi.
Malamulo Ake akutsika Pakati pa
izo kuti mudziwe kuti ndithu,
Mulungu pachilichonse ndi
Wokhoza Ndikutinso Mulungu
wachizinga Chilichonse
m'kuchidziwa.
%$&$*
t \'A %>'*•*&
1 Riziki ndi mawu a Chiarabu amene akutanthauza chilichonse chimene
chimathandiza
Surat 66. At-Tahrim Juzu 28
1237
tA *>■»
*\ *\ f.j*d\ «JJ~*»
Surayi ikuloza zina zimene zidamkwiyitsa Mtumiki (SAW)
mwa akazi ake. Choncho adadziletsa kuchita zina
mwazosangalatsa zomwe Chauta adamloleza. Ndipo wachenjeza
akazi ake pazimene iwo adachita.
Kenaka surayi ikulamula okhulupirira kuti adzitchinjirize
okha ndi mawanja awo kumoto umene nkhuni zake ndi anthu
ndi miyala. Ndipo yafotokoza kuti Mulungu sadzavomereza
madandaulo a anthu osakhulupirira pa tsiku lomaliza.
Kenaka ikuwayitana okhulupirira kuti alape kwa Mulungu
mwachoonadi. Ndipo ikuitananso Mneneri kuti achite Jihad
yaikulu pa anthu osakhulupirira ndi achinyengo ndi kutinso
awaumire mtima.
Surayi yatsiriza ndikupereka mafanizo ofotokoza kuti ubwino
wa mwamuna pabanja sungapulumutse mkazi ngati ali wopotoka
pa chipembedzo cha Mulungu. Ndipo ubwino wa mkazi pabanja
sungapulumutse mwamuna wake ku chionongeko ngati
mwamunayo ali wosokera pa chipembedzo cha Chauta.
Surat 66. At-Tahrim Juzu 28
1238
YAtjA-i
1% f.f*A\ «jj-»
Surat At-Tahrim LXVI
f g^::'^m :
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. E, iwe Mneneri(SAW)
nchifukwa ninji Ukudziletsa
chimene Mulungu Wakuloleza
kuchita? Ukufuna kukondweretsa
akazi ako (nchifukwa Chake
wachita izi?) Koma Mulungu
Ngokhululuka kwambiri
Ngwachisoni.
2. Ndithu, Mulungu
wakhazikitsa Kamasulidwe
kakulumbira Kwanu, ndipo
Mulungu Ndiye Mtetezi wanu, lye
Ngodziwa Kwambiri ndiponso
Ngwanzeru zakuya (Pamalamulo
amene wawakhazikitsa Kwa Inu). 1
3. Ndipo kumbuka pamene
Mneneri(SAW) Adauza wina mwa
akazi ake nkhani
Mwachinsinsi,choncho (mkaziyo)
Pamene adaiulula, Mulungu
o&£\&$\&\j
-^
J? 9 &9l<
1 Mkazi ndimkazi basi. Mtumiki adanena m'Mahadisi kuti sipadapezeke mkazi
amene ali wokwanira pa chinthu chilichonse kuyambira pamene dziko
tidayamba mpaka kutha kwake kupatula akazi anayi basi. Iwowa ndi awa:
Mayi Fatuma, Mayi Khadija, Mayi Mariam (Maria) ndi mayi Asiya (mkazi wa
Farawo). Kusakwanira kwa akazi pa chilichonse kumapezekanso ngakhale
mwa akazi a Mtumiki, amamsautsa Mtumiki pomuchitira nsanje ngakhale kuti
iwo amapemphera kwambiri, kawirikawiri makamaka amayi awiri awa Mayi
Aisha ndi Mayi Hafsa monga momwe zilili m'ndime 4 ya sura iyi. Mulungu
wawakalipira kwambiri m'ndime 5 ya sura yomweyi ndi m'ndime 28 ya surat
Ahzab. Koma adalapa mwachangu ndipo Mulungu adawayanja monga zilili
m'ndime 52 ya Surat Ahzab.
Surat 66. At-Tahrim Juzu 28
1239 I ™>>>
n *\ f.y*A\ *jj-*
Adamdziwitsa (Mtumiki) za
kuululidwa Kwa nkhaniyo, (ndipo
Mtumiki) Adaifotokoza mbali ina
ya nkhaniyo, Koma mbali ina
adaisiya. Pamene Adamfotokozera
(mkazi wake) Zankhaniyo adati:
"Ndani wakuuza Zimenezi?"
(Mtumiki{SAW}) adati:
"Wandiuza Wodziwa
kwambiri.Ndiponso Wodziwa
zazing'ono ndi zazikulu (Amene
sichibisika kwa lye Chobisika
chilichonse.)
4. (Amene adali ndi nsanje
kwambiri mwa Akazi ake ndi mayi
Aisha ndi mayi Hafsa. Ndipo
Mulungu adawauza Motere):
"Ngati awirinu mulapa kwa
Mulungu pazimene mwachita
(chitani Changu kulapa) chifukwa
chakuti Mitima yanu yapotoka
pang'ono (Chifukwa cha nsanje pa
zimene Mneneri akufuna zosunga
chinsinsi Chake); koma ngati
awirinu Muthandizana pazimene
zingamvutitse Ndithu, Mulungu
ndiye Mtetezi wake Ndi Jibulilu
(Gabriel). Ndiponso Asilamu
abwino; naonso angelo,
Kuonjezera apa ndiathandizi (ake).
5. Ngati (Mtumiki)
akakusuzulani, ndithu Mbuye
wake, ampatsa akazi ena m,malo
Mwa inu, abwino kuposa inu:
Ogonjera (Mulungu), okhulupirira
OjO
, --,-- '*v~H ''tsfr- KT-
-*' • -" <?*• 2 * V * V <4> " ft-
Surat 66. At-Tahrim Juzu 28
1240
TA t>i
*\*\ fLJ*A\ Sjj-**
(ndi mitima Yawo), omvera, olapa,
odzichepetsa (Pamaso pa Mulungu
ochita mapemphero Kwambiri),
oyenda (pa chikhulupiriro Cha
Mulungu kapena ochulukitsa
Kumanga) amene adakwatiwapo
Kale ndi osakwatiwapo."
6. E, inu amene
mwakhulupirira! Dzitchinjirizeni
inu ndi mawanja anu Ku moto
umene nkhuni zake ndi anthu Ndi
miyala; oyang'anira ake ndi
Angelo ouma mtima, amphamvu:
Sanyoza Mulungu pa zimene
Wawalamula, amachita (zokhazo)
Zimene alamulidwa. 1
7. (Adzawauza osakhulupirira
pa tsiku Lachiweruzo) E, inu
amene Simdakhulupirire!
Musadandaule lero, Ndithu
mukulipidwa pa zimene
Mumachita (padziko lapansi).
8. E, inu amene
mwakhulupirira! Lapani kwa
Mulungu; kulapa koona; Ndithu
Mbuye wanu akufafanizirani Zoipa
zanu ndi kukakulowetsani
M'minda momwe mitsinje
ikuyenda Pansi pake, tsiku limene
Mulungu Sadzayalutsa mtumiki
ndi amene Adakhulupirira
Akuluakulu ndiponso aliyense amene ali ndi udindo akuwalamula
kuwakonza amene ali pansi pawo powaphunzitsa chipembedzo ndi
chikhalidwe chimene Mulungu akuchifuna kuti awatchinjirize ku chionongeko.
Ngati satero ndiye kuti chilango chikafika chidzakhala cha onse.
Surat 66. At-Tahrim Juzu 28
1241
XA frjJt-*
%n {.y*A\ 5jj-*»
pamodzi naye. Dangalira lawo
lidzayenda chapatsogolo pawo ndi
mbali yakumanja Kwawo, uku
akunena: "Mbuye wathu!
Tikwanitsireni dangalira lathu
(Mpaka likatifikitse ku munda wa
Mtendere), ndiponso
tikhululukireni Ndithu Inu ndi
Okhoza chilichonse."
9. E, iwe Mneneri! Limbana ndi
Akafiri (Osakhulupirira) ndi
Amunafikina (Achinyengo),
aumire mtima.Ndipo malo Awo
ndi ku Jahannama,taonani kuipa
Kobwerera (kwawo)!
10. Mulungu wapereka fanizo la
Osakhulupirira monga mkazi wa
Nuhu Ndi mkazi wa Luti.Awiriwa
adali pansi Pa akapolo Athu awiri
abwino, koma Adali
osakhulupirika kwa amuna awo,
(Ndipo amuna awo) sadawateteze
Kalikonse ku chilango cha
Mulungu, Ndipo kudanenedwa
kwa iwo "Lowani Ku moto
pamodzi (ndi ena) olowa".
11. Ndiponso Mulungu
wapereka fanizo la Amene
akhulupirira monga mkazi wa
Firiauna (Farawo) pamene
adanena: "Mbuye wanga!
Ndimangireni, kwa inu, Nyumba
mu Jannah, ndipo ndipulumutseni
Kwa Firiauna ndi zochita zake,
<§8^##efiBaK
!Cy&J
v^&<&&&&
Surat 66. At-Tahrim Juzu 28
1242
YA tjJrl
i n ^ytsJi «jj--
ndiponso Ndipulumutseni kwa
anthu oipa (Ndi amtopola.)"
12* Ndi (fanizo lina la
wokhulupirira monga) Mariam
mwana wa Imran amene adasunga
Umaliseche wake; ndipo tidauzira
mmenemo Mzimu Wathu ndipo
adavomereza mawu a Mbuye wake
(omwe adali zolamula Zake ndi
Zoletsa Zake) ndi mabuku Ake
(amene Adavumbulutsidwa kwa
Aneneri Ake); adali Mmodzi wa
opitiriza kudzichepetsa (ndi
Kumvera Mulungu).
'f 1^6't* "^l*'!
Surat 67. AI-Mulk Juzu 29 I 1243 I Y ^ *>»
nv dWiajj-*
Surayi ikutchedwa Surat Mulk ndipo tanthauzo lake ndi
Ufumu. Yalandira dzina limeneli chifukwa chakuti mu aya
(mundime) yoyambirira mwatchulidwa mawu a ufumuwa.
Zolinga zake zenizeni ndikutembenuza maganizo ndipo maso
kuti apenye zisonyezo zamphamvu ya Mulungu yoposa,
m'mitima ndi padziko lonse, kumwamba ndi pansi; kuti
kuyang'ana kumeneko kukhale njira yokhulupirira mwa
Mulungu ndi tsiku lomaliza. Ndiponso ikulongosola zimene
zikawachitikira okana pamene azikaponyedwa ku Jahena
ndikumva mkokomo wake m'menemo uku ali kupsa. Tsiku
limenelo adzavomereza zolakwa zawo pamodzi ndi kudandaula
kwawo posalabadira za moyo wa tsiku lomaliza.
Izi zikachitika pamene angelo azikawafunsa mafunso
owadzudzula onena kuti: "Kodi sadakudzereni Aneneri ndi
kukuitanirani kwa Mulungu ndi kukuchenjezani za tsikuli?"
Koma amene adaopa Mbuye wawo ndi kumkhulupirira
akalandira chikhululuko pazimene adalakwa ndi malipiro aakulu
pazimene adachita zabwino.
Surat 67. Al-Mulk Juzu 29
1244
y<\ t&\
W diilloj^
Surat Al-Mulk LXVII
*
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Watukuka ndi kudalitsika
Amene M'manja Mwake muli
Ufiimu (Wochita Chilichonse
pazolengedwa zonse); ndipo lye ali
ndi mphamvu yokwanira
Pachilichonse.
2. Amene walenga imfa ndi
moyo kuti Akuyeseni (mayeso)
ndani mwa inu Ali wochita
zabwino (kwambiri). Ndipo lye
ndiWopambana m'mphamvu,
(Salephera kanthu); ndiponso
Wokhululukira (olakwa). 2
3. Amene adalenga thambo
zisanu ndi Ziwiri mosanjikana
(kapena zolingana Mkalengedwe
kake). Suona kusiyana M'zolenga
za Wachifundo chambiri. Bwereza
kuyang'ana; kodi ukuona Pena
pong'ambika?
o&£\<&&\&\**
J^
Sura imeneyi, Mtumiki (SAW) amafuna kuti Msilamu atiyense ailoweze
pamtima ndi kuzindikira bwino tanthauzo lake. Mtumiki (SAW) adali ndi
chizolowezi chomawerenga surayi asanagone. M'sura imeneyi muli
chikumbutso chosonyeza kuti Mulungu Ngwamphamvu amachita mmene
angafunire. Chimene wafuna chichitika ngakhale anthu sakufuna. Ndipo
chimene sanafune kuti chichitike sichingachitike ngakhale anthu atafunitsitsa
kuti chichitike. Zonse zakumwamba ndi zam'nthaka ndi Zake.
2 M'ma aya awa:- Ambuye Mulungu akutilangiza kuti tikhale oganizira zomwe
adalenga zimene zingatisonyeze nzeru Zake ndi mphamvu Zake zakuya.
Tilingalire m'zolengedwa Zake, tisalingalire mwa lye mwini chifukwa sitingathe
kumlingalira mmene alili pomwe tikulephera kuulingalira mzimu wathu momwe
ulili.
Surat 67. Al-Mulk Juzu 29 | 1245 "] T 1 *>i
nv liiiit Sjj^
4. Bwerezanso kuyang'ana
kachiwiri, Kuyang'anako
kukubwerera wekha (Uku maso)
ali olobodoka ndiponso Otopa.
(Suona polakwika paliponse).
5. Ndipo ndithu, talikongoletsa
thambo Loyandikirali ndi nyali
(nyenyezi) ndipo Tazichita
kukhala (mochokera zenje)
Zolasila asatana. Ndipo
tawakonzera (Patsiku lomaliza)
chilango Chamoto woyaka.
6. Ndipo kwa amene
sakhulupirira Mbuye Wawo ali
nacho chilango cha Jahannama;
Ndipo kuipirenji kobwerera!
7. Akadzaponyedwa
M'menemo adzamva Mavume ake
(oipa) uku ukuwira Mwaukali.
8. Udzayandikira kuphwasuka
chifukwa Cha mkwiyo (kukwiira
oipa); nthawi Iliyonse gulu (la
oipa) likadzaponyedwa
M'menemo, Angelo oyang'anira
Motowo adzawafunsa
(mowadzudzula); "Kodi
sadakufikeni mchenjezi
(Wokuchenjezani za tsikuli?)."
9. Adzayankha "Inde, adatifika
mchenjezi Koma tidatsutsa, ndipo
tidati Mulungu Sadavumbulutse
chilichonse (kwa iwe Ngakhale
kwa anzako). Koma inu muli
M'kusokera kwakukulu".
(£$ to^S ^i £^^gly5 1 13^
®M$°
Siirat 67. AI-Mulk Juzu 29
1246 I "*>i
nv ^uiiSj^
10. Ndipo adzanena:
"Tikadakhala kuti Tidamvera
(zimene ankatiuza) kapena
Kuziganizira mwanzeru
sitikadakhala M'gulu la anthu
akumoto.
11. Choncho adzavomereza
machimo awo (Koma sipadzakhala
chopindula;) Kuonongeka ndi
kukhala kutali (ndi Chifundo cha
Mulungu) kuli pa anthu Akumoto!
12. Ndithudi amene akumuopa
Mbuye Wawo pomwe iwo
sakumuona, Adzapeza
chikhululuko pa machimo Awo ndi
malipiro aakulu (pa zabwino
Zomwe ankachita).
13. Ndipo bisani mawu anu,
kapena aonetseni Poyera; (zonsezi
nchimodzimodzi kwa Mulungu)
ndithudi lye Ngodziwa Zobisika
zam'mitima.
14. Kodi asadziwe amene
adalenga (zinthu Zonse)? Pomwe
lye Ngodziwa zinthu
Zingo'nozing'no kwambiri mmene
zilili (Ndiponso) Ngodziwa nkhani
zonse.
15. lye ndi Amene
wakupangirani nthaka kuti Ikhale
yogonjera (pachilichonse chimene
Mufuna). Choncho yendani mbali
zake Zonse; ndipo idyani riziki
lam'menemo, (Limene Mulungu
%^^^&&- <aW Si
i&g\$$\&cFv>$j$
Surat 67. Al-Mulk Juzu 29 I 1247 I * * *>*
%V dUll 5j>-
akukutulutsirani). Ndipo Kwa lye
yekha ndiko kobwerera kwanu
(Nonse mtapatsidwa moyo
wachiwiri).
16. Kodi muli m'chitetezo kwa
Amene ufumu Wake uli
kumwamba kuti Sangakukwirireni
m'nthaka (Ndikukudzidzimutsani)
pamene Nthaka ikugwedezeka
molimba?
17. Kapena muli m'chitetezo
kwa Amene Ufumu Wake uli
kumwamba kuti Sangakutsitsireni
mphepo yamkuntho ya Miyala (ndi
kukuonongani ndi miyalayo?)
Choncho mdzadziwa mmene lilili
chenjezo Langa (pa inu).
18. Ndithudi amene adalipo
kale iwo Asanabadwe adakana
mithenga yawo. Nanga udali
bwanji mkwiyo Wanga pa Iwo
(pakuwaononga onse)!
19. Kodi,sadaone mbalame
pamwamba pawo Mmene
zikutambasulira (mapiko awo) ndi
Kuwafiimbata. Palibe amene
akuzigwira Kuti zisagwe koma
(Mulungu) Wachifundo chambiri;
ndithudi lye Pachilichonse
Ngopenya
20. Kodi ndani amene ali
asilikali anu Okutetezani
kuchilango posakhala (Mulungu)
Wachifundo chambiri? Ndithudi
^O ^)\ f&&\ (X&^V*
&j&a\v$jffl'j^
^J^(^2^ivwU4iIj
©.
Siirat 67. Al-Mulk Juzu 29
1248
y* *>i
IV viJLili $jj-»
osakhulupirira Ali mchinyengo
(pazimene akuganizira).
21. Kodi ndani angakupatseni
riziki (Limene mungakhalire ndi
moyo ndi Kupezera mtendere) ngati
lye Atatsekereza riziki lake (kwa
inu)? Koma Akafiri akupitiriza
kudzikweza Kwawo,ndi kudziika
kutali ndi choonadi.
22. Kodi amene akuyenda
mozyolika ndi Nkhope yake
angakhale woongoka Kapena
amene akuyenda molungama
Panjira yosakhota?
23. Nena: "lye ndi Amene
adakulengani (Pomwe simudali
kanthu) ndipo Adakupatsani
makutu, maso ndi mitima, (Zimene
mukhoza kupeza nazo mtendere):
Koma kuyamika kwanu (kwa
Yemwe Adakupatsani zimenezi)
Nkochepa kwambiri.
24. Nena: "lye ndi amene
adakuchulukitsani Padziko ndipo
kwa lye (yekha) ndiko
Mudzasonkhanitsidwa (kuti
Adzakuwerengereni ndi
kukulipirani).
25. Akunena (osakhulupirira za
kuuka Monyada): "Ndiliti
(lidzakwaniritsidwa) Lonjezo ili
ngati inu muli oona?"
26. Nena (iwe MtumikijSAW}):
"Ndithu Kudziwa (kwa izi) nkwa
©,
* **&.■.
'OX
^jmx>^$
Qca^usftWica*
Surat 67. Al-Mulk Juzu 29
1249
n *>»
"VV dlill s^
Mulungu yekha: Ndipo ndithudi ine,
ndine mchenjezi Wowonekera."
27. Koma akadzaziona (zimene
Akulonjezedwazo) zili pafupi (ndi
Iwo), nkhope za amene
sadakhulupirire Zidzakhumudwa
ndikuyaluka kwambiri Ndipo
kudzanenedwa (mowadzudzula);
"Izi ndi zija mudali kuzipempha
(Kuti zidze, zadza tsopano).
28. Nena (iwe
Mtumiki{SAW}): "Tandiuzani
Ngati Mulungu atandiononga
pamodzi Ndi amene ndili nawo
(monga momwe Mukufunira)
kapena kutichitira chifundo
(Ndikutalikitsa nthawi ya moyo
wathu). Nanga ndani amene
adzawateteza Wosakhulupirira ku
chilango Chowawa?"
29. Nena: "lye ndiye (Mulungu)
Wachifiindo chambiri,
takhulupirira mwa lye ndiponso
kwa lye ndikumene tatsamira.
Posachedwapa mudziwa (chilango
Chikatsika kuti) ndani (m'magulu
Awiriwa) yemwe ali m'kusokera
Koonekera."
30. Nena: "Tandiuzani ngati
madzi Anuwa ataphwa
(kulowerera pansi Penipeni);
choncho ndani amene
Angakubweretsereni madzi oyenda
(Ochokera mkati mwanthaka?).
$ 9 &<?*-<
&V*i 4»I(^U| t)lfttol J»
Surat 68. Al-Qalam Juzu 29
1250
Y<* >>i
*VA ^JLaJl 5jj~-
M'sura yolemekezekayi muli mawu othondoza Mneneri
(SAW) ndi kulirimbikitsa khama lake kuti apitirire kuchita
choonadi popanda kugonjera aliyense.
Mulinso fanizo la chilango chomwe chidawagwera eni
mzinda wa Makka monga chilango chomwe chidawagwera eni
munda amene nkhani yawo yakambidwa M'surayi. Ndiponso
ikupereka uthenga wabwino kwa okhulupirira pa zimene
akalandira kwa Mbuye wawo Mulungu ndikunenetsa kuti palibe
kufanana pakati pawo ndi osakhulupirira.
Surayi ikuwakanira otsutsa pazimene ankadzinyenga okha
popanda choonadi. Ndipo ikuwaopseza polongosola mmene ati
akakhalire pa tsiku lomaliza. Kenako ikulangiza Mtumiki
(SAW) kuti apirire. Ndipo yamaliza ndikulemekeza Qur'an
yolemekezeka.
Surat 68. Al-Qalam Juzu 29 1251 t * *j*-i
nA q&\ 5jj-»
Surat Al-Qalam LXVIII
m\i
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Nun, Ndikulumbirira pensulo
(imene Akulembera angelo ndi
ena), ndi Zimene amalemba.
2. Pa chisomo cha Mbuye wako
iwe Sindiwe wamisala (Pokupatsa
uneneri).
3. Ndipo ndithu, udzakhala ndi
malipiro Aakulu osaduka,
(onkerankera mtsogolo Chifukwa
cha mavuto amene Ukukumana
nawo pofikitsa uthenga).
4. Ndipo ndithu, uli nawo
makhalidwe abwino Kwambiri
(omwe Mulungu adakulenga
Nawo).
5. Basi, posachedwapa uona,
Iwonso aona
6. Kuti ndani mwa inu
wamisala (iwe kapena Iwo)?
7. Ndithu, Mbuye wako
akum'dziwa bwino Amene
wasokera panjira yake. Ndiponso
Akuwadziwa bwino Amene ali
oongoka.
8. Choncho, usawamvere
otsutsana; (Usasiye zimene uli nazo
ngakhale Sakugwirizana nazo).
o&£\<£&\&\j
-\j^
®&&lpMb
b
©Ur&ljX^,
^Xa&!i.lM
'- v^ /> ^
Surat 68. Al-Qalam Juzu 29 1252 * * *j*-»
1A ^JLaSi ojj--
9. Akufuna kuti ukadakhala
Wofewa kwa iwo (pazinthu zina)
Nawo akadakhala ofewa (kwa iwe)
10. Ndipo usamumvere aliyense
wochulukitsa Kulumbira ndiponso
woyaluka,
11. Wojeda, woyenda Ndi
ukazitape, (ndi cholinga
Choononga umodzi wawo).
12. Wotsekereza zabwino
wamtopola Ndipo wamachimo
ambiri,
13. Wouma mtima; pamwamba
pa izi Ndi wodzipachika mu
mtundu Wa ena, (pomwe iye sali
m'menemo).
14. Chifukwa choti iye ndi
mwini chuma Ndi ana (ndi zimene
ali kunyadira).
15. Zikawerengedwa kwa iye
aya Zathu Amanena: "Izi ndi
nthano za akale (Ndi zabodza
zawo, zopeka).
16. Timuika pamphuno pake
chizindikiro (Chosasiyana nacho
kuti ayaluke Nacho pamaso pa
anthu).
17. Ndithu ife tidawayesa (eni
mzinda wa Makka ndi mtendere
omwe udali pa iwo, Koma adakana
monga) momwe Tidawayesera eni
munda, pamene Adalumbira kuti
%&4&$}&&
G^'itejSsi
%;\^m^
^ayj£$i
%
9[99l\i *[' ij <"
Surat 68. Al-Qalam Juzu 29 I 1253 I Y \ *>i
^A ^JUJt 5jj--
akathyola (zipatso za M'munda
wawozo) mbandakucha (kuti
Osauka asawaone
angawapemphe).
18. Ndipo sadapatule (ngakhale
wosauka ndi M'modzi yemwe
ponena kuti uje Timpatse, uje
tisampatse, kapena Sadanene kuti,
"Ngati Mulungu afuna)."
19. Mliri woopsa wochokera
kwa Mbuye Wako udauzinga
(mundawo nthawi Yausiku) iwo ali
mtulo.
20. Choncho udakhala ngati
wokoledwa (Chifukwa cha mliri uja).
21. Adaitanizana nthawi Ya
mbandakucha.
22. "Lawirirani kumunda wanu
kuja ngati Mukufuna kukolola
(kuopera kuti Angakuoneni osauka)"
23. Adanyamuka uku
Akunong' onezana,
24. (Akunena kuti);
"Asakulowerereni Osauka lero
mmenemo".
25. Ndipo adalawirira ali ndi
chitsimikizo Choti atha kuwamana
(osauka).
26. Choncho pamene adauona,
adanena (uku Akunjenjemera):
"Ndithu ife tasokera (Sikuno ayi,
munda wathu uja suno).
^^#&fi
™?t%%
®^ 9 Ma%^&v\
%&^Z$$*&3
&u^®®&rM
Siirat 68. Al-Qalam Juzu 29 1254 Y * *>i
1A ^JUll Sjj~-
27. Iyayi, ndiwomwewo; koma
Tamanidwa zinthu zake."
28. Wolungama mwa iwo
adanena: "Kodi sindinakuuzeni
(pamene Mudali kulangizana
zomana osowa) Kuti bwanji
osamkumbukira Mulungu (Ndi
kusintha cholinga chanu)?"
29. (Iwo) adanena:
"Alemekezeke Mbuye Wathu
ndithu ife tidali a chinyengo
(Chifukwa cha kuipa kwa cholinga
Chathu)"
30. Ndipo adatembenukirana
ndikuyamba Kudzudzulana.
31. Adati: "E, chionongeko
chathu ndithu Ife tidapyola malire
(m' chinyengo chathu)
32. Mwina Mbuye wathu
angatipatse Zabwino m'malo mwa
munda wathuwu. Ndithu ife
tikufunitsitsa kwa Mbuye Wathu
(chikhululuko Chake).
33. Umo ndi mmene
chimakhalira chilango (Changa
chomwe ndimachitsitsa Padziko
lapansi kwa amene Chamuyenera);
koma chilango cha tsiku Lomaliza
nchachikulu zedi, akadakhala
Akudziwa.
34. Ndithu, oopa Mulungu
adzakhala ndi Minda ya mtendere
Kwa Mbuye wawo.
Qy*j>j*** ( -^' *t»
<^$j$$$&$3&
e^msk&&#s
9 '9 <*Al ' t
Surat 68. Al-Qalam Juzu 29 I 1255 I Y ^ *>
*\A |J^Jl 3jj-j
35. Kodi tiwachite Asilamu
monga ochimwa.
36. Kodi nchiyani chakupezani!
Nanga mukuweruza bwanji
(Maweruzo opanda
chilungamowa)?
37. Kapena muli ndi buku
limene Mukuwerenga.
38. Kuti mulinazo mmenemo
zomwe Mukuzifiina.
39. Kapena muli nawo
mapangano ndi Ife okafika mpaka
tsiku lomaliza Akuti inu
mudzapeza zimene
Mukudziweruzira?
40. Afunse (iwe Mtumiki)
Ndani mwa iwo amene ali
mtsogoleri (Pa malamulo
amenewa)?
41. Kapena iwo ali nawo
othandidzana nawo (Pa mau awa)?
Ndipo atabweretsa Othandizana
nawo ngati akunena zowona!
42. (Akumbukire) tsiku la
mavuto Okhwima, ndipo
adzaitanidwa (akafiri) kuti Achite
sijida (polambira Chauta) koma
Sadzatha.
43. Maso awo adzangoti pansi
zyoli, Manyazi ndi kunyozeka
Kudzawaphimba; kumachita kuti
adali Kuitanidwa (padziko lapansi)
*u^3£2\&&
"&*''?■»,
j&* a
««^(^
Surat 68. Al-Qalam Juzu 29
1256
t* frj*-i
*\A ^JLoJl ojj**
kuti Agwetse nkhope pansi pomwe
iwo Adali ndi moyo wa ngwiro
(Koma ankakana).
44. Ndisiye, (iwe Mtumiki), ndi
amene Akukanira nkhani iyi
tiwakokera Kuchilango
pang'onopang'ono Pamene iwo
sakudziwa (mmene chiti
Chiwadzere chilangochi)
45. Ndipo ndikuwalekerera
(pochedwetsa Chilango); ndithudi
makonzedwe Anga Ngokhwima,
(palibe angapulumuke Mmenemo).
46. Kapena ukuwapempha
malipiro (Pofikitsa uthenga) kotero
kuti iwo Akulemedwa ndi
kulipira?
47. Kapena ali nazo (nzeru)
zobisika Kotero kuti iwo akulemba
(zimene Akuweruzazo)!
48. Choncho pirira ndi lamulo
la Mbuye wako (Chifukwa
chowalekerera ndi Kuchedwetsa
chipulumutso chako); ndipo
Usakhale ngati mwini nsomba
(Yunusu pa changu ndi mkwiyo
kwa Anthu ake) pamene adaitana
(Mbuye wake) uku ali wodzazidwa
ndi Mkwiyo (kupempha kuti
chidze Mwachangu chilango kwa
anthu ake).
49. Chikadapanda kumfikira
chisomo Chochokera kwa Mbuye
©££U
<%&&%$& Q&
®,
u
%3&&4@fi*&
'f »tev1' tv '&\* >
M lpttf^**^S^ 33$
Siirat 68, Al-Qalam Juzu 29 1257 t * *j*-i
nA fJUft 5^
wake (ndi Kuvomera kulapa
kwake), Akadaponyedwa
(kuchokera m'mimba Mwa
chinsomba chija) pagombe
(Popanda kanthu) ali
wodzudzulidwa
50. Koma adamsankha Mbuye
wake (Povomera kulapa kwake)
ndipo Adamchita kukhala mmodzi
wa anthu Abwino.
51. Ndithudi anthu amene
sadakhulupirire Adayandikira
kukutereretsa ndi Kunyogodola
kwa maso awo (chifukwa
Chachidani ndi mkwiyo) pamene
Adamva chikumbutso(Qur'an),
ndipo Akunena kuti iyeyo
ngwamisala.
52. Ndipo ichi sichina, koma
(ndi phunziro, Ndi nzeru) ndi
chikumbutso kwa Zolengedwa
zonse.
®G^\&4^%^
9$^iWZ
Surat 69. Al-Haqqah Juzu 29
1258
r* *>»
*\ ^ aSU-I 3j^->
Sura yolemekezekayi, yasonyeza mmene zinthu zidzakhalire
tsiku la chimaliziro (Kiyama) ndipo yafotokoza zimene
zidawapeza anthu akale monga kuonongeka ndi chilango
champhamvu pamene adatsutsa uthenga wa Mulungu.
Yafotokozanso za kuombedwa lipenga losonyeza kutha kwa
dziko ndi zimene zidzaonekera nthaka, mapiri ndi thambo
monga kusintha ndi kuchoka; ndi zimene zidzachitika
motsagana ndi zimenezo monga anthu kuonekera kwa Mulungu
ndi kuweruzidwa pa zomwe adachita.
Surayi yapereka uthenga wabwino kwa anthu akudzanja
iamanja, ochita zabwino, kuti adzakumana ndi malipiro abwino;
umene udzakhala mtendere wamuyaya. Ndipo yawachenjeza
anthu akumanzere, ochita zoipa, kuti adzakumana ndi chilango
chowawa.
Ndipo Surayi yamaliza ndi kunena zachoonadi cha uthenga
wa Muhammad (SAW) umene adaufikitsa kwa anthu, ndi
choonadi cha Qur'an yomwe ili choonadi chochokera kwa
Mulungu.
Siirat 69. Al-Haqqah Juzu 29 1259 r <\ *>»
i ^ aiu-i Sjj--
Surat Al-Haqqah LXIX
:**-'
L-\_ £
- 4§^ -v
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Chakudza cha choonadi
(chomwe ndi Kiyama).
2. Kodi chakudza cha choonadi
nchiyani?
3. Nanga nchiyani
chikudziwitse za chakudza Cha
choonadicho?
4. Asamudu ndi a Adi adatsutsa
Zakudza kwa Kiyama (yomwe
Idzadzidzimutsa zolengedwa
Mwamphamvu ndi zoopsa zake).
5. Tsono Asamudu
adaonongedwa ndi Phokoso
lopyola muyeso, (Lamphamvu
kwambiri).
6. Ndipo Adi adaonongedwa
ndi Chimphepo cha mkutho,
chozizira, (Champhamvu
kwambiri).
7. Mulungu adaachitumiza kwa
iwo pa Usiku usanu ndi uwiri ndi
masana asanu Ndi atatu
mosadukiza; kotero Ukadawaona
ali lambalamba mmenemo Ngati
mathunthu a mitengo ya kanjedza
Yopanda kanthu m'kati mwake.
8. Kodi nanga ukumuona
wotsala mwa Iwo?
o^l^jM^U-
^
m%\
©fcait
©\3xa1u5Ljae5
<^$ffixjt>&$
(s ^\ i \^'&%&
hi^^^^%^
*&%&»&&
Surat 69. AI-Haqqah Juzu 29
1260
r* >>i
"\ ^ 43li-1 5jj-»
9. Ndipo Firiaun ndi amene
adalipo iye Asadabadwe, ndi
khamu la anthu amidzi
Yotembenuzidwa (anthu a Luti)
adadza Ndi machimo (akulu).
10. Ndipo (yense wa iwowa)
adanyoza Mtumiki wa Mbuye
wawo; choncho Adawalanga
chilango chopitirira muyeso.
11. Ndithu pamene madzi
adasefukira Mopyola muyeso
(mpaka kumeza Mapiri nthawi ya
chigumula cha Nowa) Ife
tidakukwezani mchombo
choyandama Ndi kuyenda.
12. Kuti tichichite
(chochitikacho chomwe
Okhulupirira adapulumuka nacho;
Osakhulupirira adaonongeka
nacho) Kukhala lingaliro ndi
phunziro kwa inu, Ndikuti lisunge
(nkhaniyi) khutu losunga.
13. Likadzaimbidwa lipenga,
kuimba Kumodzi kokha (zamoyo
zonse zidzafa),
14. Ndipo nthaka ndi mapiri
nkuchotsedwa M'malo mwake ndi
kuphwanyidwa Kamodzi kokha.
15. Tsiku limenelo, chakudza
Chidzakhala kuti chadza (imene ili
Kiyama).
16. Ndipo thambo lidzasweka
choncho ilo Tsiku limenelo
§>&*"*
^^2S#teM2£
Surat 69. Al-Haqqah Juzu 29 1261 I * * *&
i ^ du-i o
d jj--
lidzakhala lofooka (Pamene lidali
lolimba).
17. Ndipo Angelo adzakhala
m'mphepete Mwake, ndipo
pamwamba pawo Tsiku limenero
(Angelo) asanu Ndi atatu
adzasenza mpando wa Mbuye wako.
18. Tsiku limenelo
mudzabweretsedwa Kuchiweruzo;)
sichidzabisika chilichonse
Chobisika mwa inu.
19. Tsono amene adzapatsidwa
kaundula Wake chakudzanja
lakumanja kwake Adzanena
(mokondwa kwa amene ali
M'phepete mwake): "Tengani!
Werengani kaundula wanga!"
20. Ndithudi ine ndidatsimikiza
(padziko Lapansi) kuti
ndidzakumana ndi Chiwerengero
changa.
21. Choncho, iye adzakhala mu
moyo Wosangalatsa
22. M'munda wapamwamba.
23. Zipatso zake zoyandikira
pansi (zosavuta Kuzithyola)
24. (Adzawauza kuti:) "Idyani,
ndipo imwani Mosangalala pa
zimene mudatsogoza Mmasiku aja
adapita (apadziko lapansi).
25. Ndipo amene adzapatsidwe
kaundula Wake kudzanja lake
^t>>ws^uacK
«2$fc3U®
«£_? ViStf .<*■*'»*
&&*&$&&'&
Surat 69. Al-Haqqah Juzu 29 1262 I * * *>»
t H tflJ-l 5jj-»
lamanzere, Adzanena
(modandaula): "Kalanga ine!
Ndiponi ndikadapanda kupatsidwa
Kaundula wangayu!
26. Nkusadziwa chiwerengero
changa!
27. Ha! imfa ija
ikadandimaliziratu (Ndi
kundilekanitsa ine ndi zimenezi).
28. Chuma changa
sichidandithandize !
29. Mphamvu zanga (ndi moyo
wanga Wathanzi) zandichokera!"
30. (Kudzanenedwa kwa angelo
Oyang'anira Jahena): Mgwireni
ndipo Mnjateni (pomphatikiza
manja ndi Khosi)!
31. Kenako mponyeni kumoto.
32. Kenakonso mlowetseni
mtcheni lotalika Mikwamba
makumi Asanu ndi awiri!
33. Ndithudi, iye sadali
Kukhulupirira mwa Mulungu
wamkulu.
34. Sadalinso kulimbikitsa
Zodyetsa osauka.
35. Basi, lero kuno Alibe
bwenzi (lomthandiza).
36. Ndipo alibe chakudya
kupatula Mafinya (a anthu
akumoto)
®^^ics^c$&
©^*(JWfc
v*i>2 Uj*4-- V^eja jO-J- Jt,>>
tS&K&fr* 1 "«
h$frfr.%%\3L&
Surat 69. AI-Haqqah Juzu 29 I 1263 I Y ^ *>i
*\ ^ AdU-l 5jj-a
37. Zomwe palibe angazidye
kupatula Ochimwa (mwadala).
38. Choncho ndikulumbirira
zimene Mukuziona,
39. Ndi zimene simukuziona.
40. Ndithudi iyi (Qur'an)
ndiliwu la Wamthenga
wolemekezeka (Jibril).
41. Ndipo simawu a mlakatuli
Ndi zochepa zimene
Mukuzikhulupirira.
42. Ndiponso simawu A mlosi;
ndi zochepa Zimene
mumalangizika nazo!
43. (Ichi ndi) chivumbulutso
Chochokera kwa Mbuye wa
zolengedwa.
44. Ndipo (Mneneri)
akadatipekera Bodza lililonse.
45. Tikadamgwira
mwamphamvu,
46. Ndipo tikadadula mwa iye
mtsempha Wamoyo (kotero kuti
ndikuferatu Nthawi yomweyo),
47. Sipakadapezeka aliyense
mwa inu Womteteza (kuchilango
Chathu).
48. Ndithu, iyi (Qur'an) ndi
phunziro Labwino kwa owopa
(Mulungu.)
©J
'%
®m%&®>
Siirat 69. Al-Haqqah Juzu 29 1264 * * *j*-i
n ^ 4dU-i ojj--
49. Ndithu Ife, tikudziwa kuti
ena mwa inu Atsutsa (Qur'an)
50. Ndipo ndithu, iyi (Qur'an)
idzakhala Chowadandaulitsa
(chachikulu) Osakhulupirira
(pamene adzaona Chilango chawo
ndi mtendere wa Okhulupirira).
51. Ndithu, iyoyi ndi choonadi
Chotsimikizika; (mulibe chikaiko),
52. Basi, lemekeza dzina la
Mbuye wako Wamkulu (Pitiriza
kutamanda dzina Lake).
®yg\&ttii
i^OpA^*
Surat 70. Al-Ma'arij Juzu 29 1265 * * *>»
V * jr jt*^ «j>-»
M'surayi muli zoopseza za tsiku la Kiyama ndikuti
lidzakhala lalitali kwambiri pamodzi ndi zoopsa zazikuluzikulu.
Ndi kuti tsiku limenelo munthu adzayesa kupereka dipo la ana,
mkazi wake, m'bale wake makolo ake ndi zonse za m'dziko kuti
apulumuke kuchilango chamoto, koma zonsezo
sizidzavomerezedwa.
Surayi yalongosolanso kuti munthu ngofooka kwambiri pa
nthawi yamavuto ndi nthawi yopeza bwino, kupatula amene
Mulungu wawateteza kukhalidwe loipa pakulimbikitsa mitima
yawo kuopa Mulungu yekha ndi kugwira ntchito yabwino,
osatekeseka ndi chilichonse ngakhale chiopse chotani.
Surat 70. Al-Ma'arij Juzu 29 | 1266 | * ^ *jk-\ V » £J uH o^
Surat Al-Ma'arijLXX
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Wopempha adapempha kuti
chiwadzere Msanga chilango
chopezekacho, (M'kupempha kwa
chipongwe ndi Kotsutsa)
2. Kwa okanira palibe
Angachitsekereze,
3. Chochokera kwa Mulungu
Mwini Makwerero.
4. Angelo ndi Jiburil amakwera
kwa lye (Mulungu) m'tsiku
Lomwe kutalika kwake kuli ngati
zaka Zikwi makumi asanu (50 000).
5. Choncho, pirira (iwe
Mtumiki{SAW} Kupirira
kwabwino,
6. Ndithu, iwo akuona (tsiku) la
Kiyama kuti palibe; silingachitike.
7. Koma Ife tikuona kuti
ndilochitika.
8. Tsiku limene thambo
lidzakhala Ngati mtovu
wosungunuka.
9. Ndipo mapiri adzakhala ngati
ubweya (Wongouluka wokha).
10. Ndipo m'bale sadzafunsa Za
m'bale wake,
Q^lfc^JJl^
-£
Surat 70. Al-Ma'arij Juzu 29 1267 * * >>
V* ?r jUil 3
£j mn fljj^
11. Ngakhale adzawalole kuti
aonane Ndi kudziwana pakati
pawo (Sadzafunsana).Wochimwa
adzalakalaka Kuti
akadaziwombola ku chilango cha
Tsiku limenelo ndi ana ake,
12. Ndi mkazi wake, ndi m'bale
wake,
13. Ndi akurntundu wake amene
Amamsunga.
14. Ndi (kulipira) zonse Za
m'dziko, kuti Zimpulumutse.
15. Iyayi, (siya iwe wamachimo
zimene Ukulakalakazo)! Ndithu
umenewu ndi Moto wa malawi.
16. Wosupula mwamphamvu
khungu,
17. Udzaitana (potchula dzina la
aliyense) Amene
adachitembenuzira msana Choona
ndi kunyoza;
18. Adasonkhanitsa (chuma)
ndi kusunga (M'nkhokwe zake
popanda Kuperekera chopereka
cha Mulungu)
19. Ndithu, munthu
walengedwa kukhala Wosapirira.
20. Mavuto akamkhudza amada
nkhawa.
21. Koma zabwino
zikamkhudza amamana (Ena ndi
kuiwala mavuto amene adali Nawo).
&is<sws&
Surat 70. Al-Ma'arij Juzu 29 1268 * * *>
V • £jt*il 5jj-»
22. Kupatula opemphera, (iwo
alibe mbiri Zoipazi).
23. Iwo amene akupitiriza
mapemphero Awo; (sakuwaleka
ngakhale zivute Chotani).
24. Ndi amene mchuma chawo
muli Gawo lodziwika,
25. La wopempha ndi
wosapempha.
26. Ndi amene akuvomereza za
tsiku La malipiro (ndi
kumalikonzekera.)
27. Ndi iwo amene akuopa
chilango Chochokera kwa Mbuye
wawo,
28. Ndithu, chilango cha Mbuye
wawo Nchosapulumuka nacho
(munthu Woipa).
29. Ndiponso iwo amene
akusunga Umaliseche wawo
(posachita Chiwerewere),
30. Kupatula kwa akazi awo ndi
Amene manja awo akumanja
apeza; Ndithu, pazimenezo iwo
Sangadzudzulidwe.
31. Koma amene angafune
(zina) Kusiya zimenezi iwowo
ndiwo Olumpha malire.
32. Ndi iwo amene amasunga
mwaubwino Zimene
amasungisidwa ndi zimene
alonjeza.
'&" !
tft
9 m' [<''*W9J> *9 •til'
Surat 70. Al-Ma'arij Juzu 29 [ 1269 | * * *& V * g- jUlt *^
33. Ndi iwo amene amaima
molungama Popereka umboni
wawo.
34. Ndiponso iwo amene
amasunga (Mwaubwino)
mapemphero awo.
35. Amene ali ndi mbiri
zimenezi adzakhala M'minda
(yamtendere) ali Olemekezedwa.
36. Kodi kuli chiyani kwa
amene akana (Chikhulupiriro)
akuthamangira kwa iwe (Maso ali
pamtunda)?
37. Atakuzungulira ena
chakumanja ena Chakumanzere
atazungulira.
38. Kodi akulakalaka aliyense
mwa iwo Kuti akalowetsedwe ku
munda Wamtendere?
39. Asiye (kukhumba kwawo
kokalowa ku Munda wa
mtendere)! Ndithu Ife
Tidawalenga kuchokera m'zimene
Akudziwa! (madzi opanda pake).
40. Ndikulumbirira Mbuye wa
kuvuma ndi Kuzambwe konse
ndithu Ndife Wokhoza.
41. Kuwasintha ndi kudzetsa
abwino Kuposa iwo; Ife palibe
(chilichonse) Chotipambana.
42. Asiye azingolankhula
zopanda pake ndi Kumangosewera
S?\i SS 9 S* t S
®wG& ti^lfc^gM tf
*j& &&<&!*$%
$ayaty
Surat 70. Al-Ma'arij Juzu 29 | 1270 | Y^ *£\ V * ^jUli Sjj-
mpaka adzakumane Ndi tsiku lawo
limene Akulonjezedwa.
43. Tsiku limene adzatuluke
m'manda Uku akuthamanga
(kudza kwa woitana) Ngati kuti
akuthamangira kumafano awo
(amene adali Kuwapembedza).
44. Maso awo ali zyoli,(osatha
kuwakweza); Kuyaluka
kutawaphimba! Limenelo Ndilo
tsiku lomwe adali kulonjezedwa
(Pomwe adali padziko lapansi.
&\ty%^gffify?>
^SlyW^
Surat 71. Nuh
Juzu 29 I 1271 T * *j*-i
v y ^y 5 j^
SURAT NUH LXXI
Surayi yafotokoza mwatsatanetsatane nkhani ya Nuhu (AS)
pamodzi ndi anthu ake. Ndipo yafotokozanso za kuitana kwake
kwa anthu ake molimbika, kenako mobisa, ndipo kenakonso
molimbika. Ndiponso yalongosola kusuma kwake kwa Mulungu
za kusalabadira kwawo ndi makani awo. Yanenanso za
kupitiriza kwawo kugwadira mafano mpaka adayenera kulandira
chilango cha Mulungu.
Pamene Nuhi adataya mtima pazakuvomera kwawo
pakuitana kwake, adapempha Mulungu kuti awaononge onse ndi
kuwathetsa.
Kenaka adadzipemphera yekha kudzanso makolo ake,
okhulupirira aamuna ndi aakazi, kuti Chauta awakhululukire.
Surat 71. Nuh
Juzu 29
1272
r^ *>i
v^
C>'.» <
Surat NuhLXXI
m
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Ndithu Ife tidamtuma Nuhu
kwa Anthu ake, (ndikumuuza
kuti): "Chenjeza anthu ako
chisadawafike Chilango
chowawa."
2. Adanena (Nuhu), "E, inu
anthu anga! Ndithu, ine
ndimchenjezi kwa inu Woonekera
poyera (wolongosola za Uthenga
wa Mbuye wanu M'chiyankhulo
chimene mukuchidziwa).
3. Mpembedzeni Mulungu
ndipo muopeni Ndikutinso
mundimvere (Pazimene
ndikukulangizani).
4. (Ngati mutero)
adzakukhululukirani Machimo anu
ndi kukutalikitsirani moyo Wanu
kufikira m'nthawi imene yaikidwa
(Kuti ndiwo malire akutalika kwa
Moyo). Ndithu nthawi ya Mulungu
Ikabwera siyichedwetsedwa
(Ngakhale pang'ono).
Mukadakhala Mukudziwa.
5. Adanena (Nuhu): "Ambuye!
Ine Ndaitanira anthu anga
(Kuchikhulupiriro) usiku ndi usana
(Popanda kufooka).
§yi^ £ .; *■$£:>■
o^t^jii^u-
-a
®y£kVji&\j&\\j!&\y\
t\ 9 '\ >* 9 i 9 *" 9 \l,» '
©Ij^iJ
Surat 71. Nuh
Juzu 29
1273 ™*j*-»
V>
C> 5 J>"
6. Kuitana kwanga
Sikudaonjezere (chilichonse) koma
Kuthawa basi (kuchikhulupiriro
Chanu).
7. Ndipo ine nthawi iliyonse
ndikawaitanira (Ku chikhulupiriro
Chanu) kuti Mwakhululukire,
akuika zala zawo M'makutu
mwawo (kuti asamve Uthenga
Wanu), ndipo akudziphimba Ndi
nsalu zawo (kuti asaone nkhope
Yanga), ndipo akupitiriza kukana
Kwawo ndi kudzikweza kwakukulu.
8. Kenaka ine ndawaitanira
(kwa Inu) Ndi mawu ofuula,
9. Kenakanso (ine
ndawaitanira) Molengeza poyera
ndiponso Mwachinsinsi mobisa.
10. Choncho ndidati (kwa anthu
anga): Pemphani kwa Mbuye wanu
chikhululuko (Pa kukana kwanu
ndi kutonza kwanu): Ndithu, lye
sadasiye kukhala Wokhululukira
(machimo kwa amene Akubwerera
kwa lye).
11. Akutumizirani mvula
yotsika Mochuluka,
12. Ndikukupatsani chuma ndi
ana, (Zomwe ndi zokongoletsa za
dziko Lapansi), ndi kukupangirani
minda (Yokongola) ndi
kukupangirani mitsinje (Yothirira
mbewu zanu ndi kumwetsa Ziweto
zanu).
<m3m^kkfc
Surat 71. Nuh
Juzu 29
1274
Y<\ ftjJb-i
V ^ c y 5 j^
13. Kodi chifukwa ninji
simupereka Ulemu kwa Mulungu
(woyenera Umulungu Wake kuti
akakuchitireni Chifundo ndi
kukupulumutsani ku Chilango),
14. Pomwe lye adakulengani
Mnjira zosiyanasiyana: (Madzi a
umunthu, kenako Magazi, kenako
magazi Ochindikara, kenako
Mafupa ndipo kenako mnofu),
15. Kodi simudaone momwe
Mulungu Adalengera thambo
zisanu ndi Ziwiri mosanjikizana?
16. Ndi kuupanga mwezi
mthambomo Kukhala kuunika,
ndiponso Kulipanga dzuwa
kukhala nyali.
17. Ndipo Mulungu
adakulengani Kuchokera m'nthaka
monga mmera.
18. Kenako adzakubwezerani
Momwemo
ndikudzakutulutsaninso (Popanda
cholepheretsa).
19. Ndipo Mulungu
wakupangirani Nthaka kukhala
ngati choyala,
20. Kuti muziyendayenda
m'menemo M'njira zazikulu."
21. AdanenaNuhu: "Ambuye!
Ndithu Anthu anga andinyoza
(pazimene Ndawalamula kuti
©B&A&S&tffc
®\$\£\p&.
t I " '9 '
^<®£j#*a6
&\X£$titi£'&.i%>j£
o»
Surat71.Nuh
Juzu 29
1275
M *>i
v^
C> i»*
akhulupirire Inu ndi kupempha
chikhululuko Chanu), ndipo
(ofooka mwa iwo) Amtsatira
yemwe chuma chake ndi ana Ake
sizidzamuonjezera (chilichonse
Chabwino) koma kutaika (ndi
Kuonongeka patsiku lomaliza).
22. Ndipo (eni chuma ndi ana)
awatchera (Otsatira awo) ndale
zazikulu (Ndi zopyola muyeso kuti
Asakhulupirire)"
23. Ndipo adanena (kwa otsatira
awo): "Musasiye kupembedza
milungu Yanu: Musamusiye
Wadda, Suwaa, Yaghutha, Ya'uka
ndi Nasra (Maina amafano awo)."
24. Ndipo ndithu iwo asokeretsa
(anthu) Ambiri; ndipo
musawaonjezere ochita Zoipa
(china chake) koma kusokera basi"
25. Chifukwa cha zochimwa
zawo Adamizidwa ndi
kulowetsedwa kumoto (Waukulu
woyaka); sadapeze Owapulumutsa
ndi kuwateteza m'malo Mwa
Mulungu.
26. Ndipo adanena Nuhu
(atataya mtima Za anthu ake):
"Ambuye! Musasiye Aliyense
mwa osakhulupirira kukhala
Padziko.
27. Ndithu, Inu Ambuye ngati
muwasiya (Popanda kuwaononga
WX$fpiJ&
*w^
'"■&m-.
&UkW5fc«l$l
Surat 71. Nuh
Juzu 29
1276 t**>i
V 1 £> ijy*
ndi kuwathetsa) Asokeretsa
akapolo anu (kunjira Yolungama).
Ndipo sangabereke (ana Abwino)
koma oipa; osakhulupirira (Okhala
kutali ndi choonadi, ndiponso
Onyoza Inu).
28, "Mbuye wanga!
Ndikhululukireni ndi makolo
Anga, ndi aliyense walowa
M'nyumba yanga ali okhulupirira
Ndi okhulupirira aamuna ndi
okhulupirira Aakazi. Ndipo
musawaonjezere anthu
Achinyengo chinachake koma
Kuwaononga basi."
«6ttf iwfeasyssu
Surat 72. A 1- Jinn Juzu 29
1277
t* *j*-1
VY jA-iaj^-
Mulungu walamula Mneneri wake (SAW) msurayi kuti
adziwitse anthu zimene zavumbulutsidwa kwa lye zoti ziwanda
zidamvera kuwerenga kwake kwa Qur'an ndipo zidavomereza
uthenga wake. Ndiponso izo zidafotokoza mmene opulukira
mwa iwo kudzanso abwino awo, adalili. Ndi kuti zinkakhala
m'malo okhala nkumamvera nkhani za kumwamba mobera.
Koma tsopano akuzipirikitsa.
Ma aya a surayi asonyeza njira za Chisilamu kwa olungama
ndi osalungama. Ndipo afotokoza kuti mapemphero ndi misikiti
zikhale za Mulungu yekha. Ndiponso yafotokoza zoti ziwanda
zidamzinga Mtumiki Muhammad(SAW) kumverera Qur'an
yomwe adali kuwerenga.
Surayi yafotokozanso kuti pali zina zimene Mtumiki (SAW)
angazithe ndipo pali zina zimene sangazithe. Ndipo
yachenjezanso onyoza Mulungu ndi Mtumiki Wake kuti
akalowa kumoto. Pomaliza yanenetsa kuti Mulungu yekha ndiye
akudziwa.
Surat 72. Al-Jinn Juzu 29 1278 * * *>»
vr jfclSjj-
Surat Al-Jinn LXXII
*§u ^*^
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Nena (iwe Mtumiki(SAW),
kwaanthu Ako):
"Kwavumbulutsidwa kwa Ine kuti
gulu la ziwanda lidamvetsera
(Kuwerenga kwanga Qur'an)
ndipo Lidanena (kumtundu wawo),
ndithu, Tamvetsera Qur'an
yodabwitsa, (Sitidaimve yonga iyi
chiyambire).
2. Ikuitanira kuchilungamo,
ndipo Taikhulupirira. Ndipo
sitimphatikiza Aliyense ndi Mbuye
wathu, (pa Mapemphero.)
3. Ndipo ndithu, ukulu ndi
ulemerero wa Mbuye wathu
watukuka; Sadadzipangire mkazi
kapena mwana.
4. Ndipo ndithu, mbuli za mwa
ife zakhala Zikunenera Mulungu
mawu abodza (Okhala kutali ndi
choonadi).
5. Ndipo ndithu ife tinkaganiza
kuti Anthu ndi ziwanda
sangamnenere Mulungu zabodza
(zosayenera Ulemerero Wake).
6. Ndipo ndithu, padali amuna
amuwanthu Amapempha chitetezo
kwa amuna Amziwanda, ndipo
o^l^JII^L,
— Z&
:\ '*
i^H3M%&$$m
y k * 'f ' /i '
Siirat 72. Al-Jinn Juzu 29
1279
Y<\ *>»
VY^lSj^-
adawaonjezera (Amuna
amziwanda) kupitiriza Machimo
awo, kupulukira (ndi Kuchenjerera
anthu.)
7. Ndipo iwo amaganiza monga
momwe Mumaganizira inu kuti
Mulungu Sadzaukitsa aliyense
(atafa).
8. Ndithu, ife tidafuna kukafika
Kumwamba; tidakupeza kutadzala
Alonda (Angelo) amphamvu ndi
Zenje zamoto.
9. Ndithu ife tidali kukhala
m'menemo (Kale) mokhala
momvetsera; (mobera Nkhani
zakumwamba). Koma amene
Afune kumvetsera tsopano apeza
chenje Chamoto chikudikirira (kuti
chimgwere lye ndi kumuononga).
10. Ndithu, ife sitikudziwa
chilango Chimene akuwafunira
am'dziko (Polondera kumwamba,
kuletsa Kumvetsera nkhani
zakumeneko); Kapena Mbuye
wawo akuwafunira Zabwino ndi
chilungamo (pazimenezo).
11. Ndithu, ena mwaife ndi
abwino Koma ena sali
choncho.Tili njira Zosiyanasiyana.
12. Ndithu ife tidadziwa kuti
Mulungu Sitingathe kumlepheretsa
(lamulo Lake Pa ife paliponse
tingakhale) padziko Lapansi, ndipo
©tou>3
Surat 72. Al-Jinn Juzu 29
1280
^ *>i
Vt^lo^j^
sitingamlepheretsenso Pomzemba
ndi kuthawira (kumwamba)
13. "Ndipo ife pamene tachimva
chiongoko (Qur'an) tachikhulupirira
ndipo amene ati Akhulupirire mwa
Mbuye wake saopa
Kumchepetsera (chabwino kapena
Kumuonjezera machimo ake).
14. Ndithu, mwa ife alipo
Asilamu Ndiponso mwa ife alipo
opatuka (Munjira ya chilungamo);
amene Walowa m'Chisilamu,
iwowo ndi Amene alunjika njira ya
choonadi.
15. Koma opatuka (kunjira ya
Chilungamo) adzakhala nkhuni za
Jahannama."
16. Ndithu, (anthu ndi ziwanda)
Akadalungama panjira Ya
chilungamo Tikadawamwetsa
madzi ambiri (Okwanira nyengo
zonse),
17. Kuti tiwayese ndi zimenezo
(mmene Angamyamikire Mulungu
pa mtendere Wake pa iwo). Koma
amene anyozera Kupembedza
Mbuye wake, amlowetsa
Kuchilango chovuta (chimene
Sangathe kupirira nacho).
18. Ndithu,misikiti ndi ya
Mulungu yekha! Choncho,
musapembedze aliyense Pamodzi
ndi Mulungu.
MP&&te^*3\m
Surat 72. Al-Jinn Juzu 29
1281 "*>»
vr jjfc-i *>>.
19. Ndipo ndithu, pamene
adaima kapolo Wa Mulungu
(Muhammad{SAW}, pa Swala
yake) uku akumpembedza
(Mulungu), ziwanda zidatsala
pang'ono Kumgwera (chifukwa
cha kuchuluka Kwawo ndi
kumzinga podabwa ndi Zimene
adaziona ndi kuzimva).
20. Nena:"Ndikumpembedza
Mbuye wanga M'modzi (Yekha)
ndipo Sindingamphatikize ndi
aliyense (M'mapemphero Ake)."
21. Nena: "Ine ndilibe udindo
wokupatsani Mavuto kapena
chilungamo (Ndi zabwino)."
22. Nena: "Ine palibe
anganditeteze Kuchilango cha
Mulungu (ngati Nditamnyoza)
sindingapeze malo (Othawira
kuchilango Chake) Kupatula kwa
lye.
23. Koma mphamvu imene ndili
nayo Ndikufikitsa uthenga wa
Mulungu umene
Adanditumizira;ndithu amene
anyoza Mulungu ndi Mtumiki
Wake (ndi Kupatuka pa
chipembedzo cha (Mulungu)
Ndithu, moto wa Jahannama ndi
Wake akakhala m'menemo
Muyaya.
24. Mpaka pomwe adzaziona
zimene Alonjezedwa ndipamene
^MSi^Gfe^a*
©lo>|
©i«USJ!W^9<8#
Surat 72. Al-Jinn Juzu 29
1282
Y* *j*-l
VY Jr\ Sjj-
adzadziwa (Kuti) kodi ndani
mwini mthandizi Wofooka
ndiponso wochepekedwa
Kuchuluka (kwa omtsatira, iwo
kapena Asilamu)."
25. Nena (kuti): "Sindikudziwa
ngati Zomwe mukulonjezedwa (za
chilango) Zili pafupi, kapena
Mbuye wanga Azitalikitsa.
26. (lye) ndi Wodziwa
zobisika; Sazionetsa zobisika Zake
kwa Aliyense (mzolengedwa Zake),
27. Kupatula Mtumiki (Wake)
amene Wamuyanja; (iyeyo
amamdziwitsa Zobisikazo) ndipo
ndithu amamuikira Alonda
kutsogolo kwake ndi Kumbuyo
kwake (omulonda).
28. Kuti adziwe ngati afikitsa
Uthenga wa Mbuye wawo, ndipo
Wawazungulira (podziwa zonse
Zili kwa iwo) ndipo wadziwa
Kuchuluka kwa zinthu zonse
Zimene zilipo; (palibe chobisika
Kwa lye)."
feWwo^Sf &&%2J»p*
t L? 'f
©bU*>
Surat 73. Al-Muzzammil Juzu 29
1283
r* *>i
vr jjijii Sj^
SURAT AL-MUZZAMMIL LXXIII ^ *
M'surayi Mulungu akulamula Mneneri Wake (SAW) kuti
aziima gawo lalikulu la usiku kupemphera ndi kuwerenga
Qur'an mofatsirira.
lye ndi gulu la omtsatira ake, adaima kupemphera potsatira
lamuloli. Koma kenako Mulungu adawapeputsira powalamula
kuti azipemphera Swala zisanu ndi kupereka zakati ndi sadaka,
ndiponso ndi kuchulukitsa kupempha chikhululuko Chake.
Adamlamulanso kupirira pazimene akumuyankhulira otsutsa
pomuuza kuti amsiire Mulungu, lye ndiye amene adziwe
chochita nawo.
Osakhulupirira aopsezedwa m'surayi powauza kuti awalanga
ndi chilango choopsa monga chomwe adalangidwa nacho anthu
akale amene adali kunyoza Mneneri wa Mulungu. Ndipo
aopsezedwanso ndi zoopsa zina zomwe zidzachitika tsiku
lomaliza.
Surat73.Al-MuzzammilJuzu29 1284 t ^ *j*-t
vr »i i iy *
Surat Al-Muzzammil LXXIII
;
M&ffiv
3^
=£=, ,_
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Ee, iwe wadziphimba (ndi
nsalu!)
2. Imirira usiku (upemphere),
Kupatula nthawi yochepa.
3. Theka lake kapena chepetsa
thekalo Pang'ono (mpaka ufike
chimodzi Mwazigawo zitatu za
usiku).
4. Kapena wonjezapo (mpaka
ufike zigawo Ziwiri mwa zigawo
zitatu za usiku;) Ndipo werenga
Qur'an mofatsa (Lemba ndi
lemba).
5. Ife tikuvumbulutsira iwe
(Mneneri) Mawu olemera (yomwe
ndi Qur'an).
6. Ndithu, kudzuka usiku Ndi
kuchita mapemphero
Kumalowerera (mumtima)
Kwambiri, ndipo zoyankhula Zake
zimakhala zoongoka ndi Zolunjika
bwino (kuposa Mapemphero
amasana).
7. Ndithu, masana uli ndi
Zochitachita zambiri;
(Umatanganidwa ndi ntchito
Yauthenga; dzipatse danga Usiku
polimbika kupemphera).
OJ&&\i£&\&\j
-^
mm
©^>'lU^^ia^&
Surat 73. Al-Muzzammil Juzu 29 1285 * * *>>
vr » o^j-
8. Ndipo tchula dzina la Mbuye
wako (Amene adalenga ndi kulera
zinthu), Ndipo udzipereke
kwathunthu kwa lye.
9. (lye ndiye) Mbuye wa
kuvuma ndi Kuzambwe; palibe
wopembedzedwa Mwachoonadi
koma lye. Mchiteni Kukhala
mtetezi (warm pazinthu Zanu
zonse).
10. Ndipo pirira pa zimene
akunena. Ndipo apewe (ndi mtima
wako); Kupewa kwabwino.
11. Ndisiye Ine ndi otsutsa eni
Kupeza bwino; ndipo alekerere
Kanthawi kochepa.
12. Ndithudi, tili ndi
mitundumitundu Ya unyolo ndi
moto Woyaka,
13. Ndi chakudya chotsamwitsa
Ndi chilango chowawa.
14. Tsiku limene nthaka ndi
mapiri Zidzagwedezeka;
(kugwedezeka kwa Mphamvu
kotero kuti) mapiri adzakhala
Ngati mulu wa mchenga
woyoyoka.
15. Ndithu, Ife takutumizirani
Mthenga Amene adzakhala mboni
yanu (tsiku la Chimaliziro; monga
momwe Tidamtumizira (Musa)
kukhala Mtumiki kwa Firiauni.
®%tf%sim&
&&$&%
Surat 73. Al-Muzzammil Juzu 29
1286
t* *jtr\
vr >jii Sj^
16. Koma Firiauni adamnyoza
Mtumikiyo; Ndipo tidamulanga
Chilango chokhwima.
17. Kodi mungadzitchinjirize
chotani ngati Mukana (chilango
cha) tsiku (lomwe) Lidzachititsa
ana kukhala ndi imvi?
18. Thambo (pamodzi ndi
mphamvu zake Ndi kukula
kwake), lidzang'ambika (Tsiku
limenelo) chifukwa cha kuopsa
Kwa tsikulo, lonjezo la (Mulungu)
Lidzakwaniritsidwa, (palibe
wolipinga).
19. Ndithudi, ma ay a awa
(amene akunena Za kuwopsa kwa
Kiyama) ndi Chikumbutso,
choncho amene akufuna
(Kuthandizika nawo) ayende
panjira Ya Mbuye wake
(pokwaniritsa Malamulo Ake ndi
kuleka zoipa).
20. Ndithu, Mbuye wako
akudziwa kuti Iwe ukuima
(kupemphera) Pafupifupi zigawo
ziwiri mwa Zigawo zitatu za usiku
kapena theka Lake, kape'nanso
chigawo chimodzi mwa Zigawo
zitatu za usiku, pamodzi ndi gulu
La omwe uli nawo. Ndipo
Mulungu NdiAmene amadziwa
bwino muyeso Wa (nthawi za )
usiku ndi usana, Wadziwa kuti
simungathe kuwerenga Zimenezo,
©jk***
o*9' m Yy >.?4 9 9 S 9 ? frs '
Surat 73. Al-Muzzammil Juzu 29
1287
™ >>i
vr »i s^
choncho wakukhululukirani.
Werengani ndime imene yapepuka
Yochokera m'Qur'an. Wadziwa
kuti ena mwa inu adzakhala
Odwala: (kudzawavuta kuimirira
ndi Kuchezera usiku), ndipo ena
adzakhala Akuyendayenda padziko
(ndi cholinga Cha malonda ndi
ntchito) kunka Nafunafuna ubwino
wa Mulungu. Ndipo ena adzakhala
akumenya Nkhondo panjira ya
Mulungu (Ncholinga chotukula
mawu Ake), Werengani chimene
chapepuka chochokera mmenemo
(m'Qur'an) ndipo Pitirizani
kupemphera swala, perekani
chopereka (chimene
chakakamizidwa Kwa inu). Ndipo
mkongozeni Mulungu Ngongole
yabwino ndipo chilichonse
chabwino chimene
mwadzitsogozera mudzachipeza
kwa Mulungu chili chabwino
(kuposa zomwe mudazisiya
m'mbuyo) ndi malipiro aakulu
zedi ndipo mpempheni Mulungu
chikhululuko (Pa uchimo wanu ndi
chikhululuko pakunyozera kwanu
kuchita zabwino). Ndithu,
Mulungu Ngokhululuka
Ngwachisoni.
Surat 74. Al-Muddaththir Juzu 29
1288
r* *>i
Vt yall 3j^
Surayi ikulamula Mneneri wa Chauta (SAW) kuti achenjeze
anthu ake ndi kuti alemekeze Mulungu. Ndi kutinso asiye
zosayenera kuchita ndi lye. Ndipo yafotokozanso za kuimbidwa
kwa lipenga ndi kukhwima kwa chilango kwa okanira.
Ikulamuliranso kuti am'siye wokana chisomo cha Mulungu
yemwe amakhumba kuti awonjezeredwe zina popanda
kuthokoza Mwini chisomo. Ndipo yafotokozanso mmene
ankaganizira osakhulupirira Qur'an.
Kenako Surayi yakumbutsa mitima kuti kalikonse kabwino
ndi koipa kamene ikuchita, ndichikole cha mitimayo. Ndipo
kenako yayankhula za anthu ambali ya kumanja mmene
azikawafunsira mafunso anthu a kumoto owaliritsa nawo kuti:
"Nchiyani chakulowetsani ku moto?"
Surayi yamaliza ndi kufotokoza za ulemerero wa Qur'an
ponena kuti umenewu ndi uthenga wabwino kwa amene
akuulingalira, ndi kunenetsa kuti amene waulingalira uthenga
umenewu akhala m'gulu la oopa Mulungu, amene adzapeza
chikhululuko Chake.
Surat74.Al-MuddaththirJuzu29 1289 T^tjJri
Vt j>&\» iy *
Surat Al-Muddaththir LXXIV
m^w r
jm&
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Ee, iwe wadziphimba (nsalu)!
2. Imirira ndipo uwachenjeze
(Anthu za chilango cha Mulungu)
3. Ndipo Mbuye wako (yekha)
Umkulitse (pomulemekeza).
4. Ndipo nsalu zako uziyeretse
(Ndi madzi kuuve).
5. Ndiponso zoipa (monga
mafano Ndi zina zonse ) zipewe.
6. Usapatse (anthu) ncholinga
Choti ulandire zambiri.
7. Chifukwa cha Mbuye Wako,
pirira (kumalamulo Ake poleka
Zomwe waletsa ndi kuchita zimene
Walamula).
8. Likadzaimbidwa lipenga,
9. Tsiku limenelo lidzakhala
Tsiku lovuta.
10. Kwa osakhulupirira,
silidzakhala Lofewa.
11. Ndisiye ndiamene
Ndidamlenga Ndekha,
12. Ndipo ndampatsa chuma
chambiri.
13. Ndi ana okhala nawo
(paliponse).
o^JJt^Jtt^
^
Sao®
&y&A*r
(?£jb3&Qj
©t^^ycJj
Surat 74. AUVluddaththir Juzu 29 1290 t H *>t
Vi yjdiSj^
14. Ndipo ndamkonzera
(ulemerero), Kumkonzera
(kwabwino).
15. Kenako ali ndi dyera kuti
Ndimuonjezere (zina popanda
Kuthokoza).
16. Koma sichoncho! Ndithu,
iye Adali kutsutsa Zizindikiro
Zathu.
17. Ndidzamkakamiza
kuchilango Chovuta: (kukwera
phiri lakumoto Limene sakatha
kulikwera).
18. Iye adalingalira (mumtima
Mwake) ndi kukonza bwino
(Chonena chonyoza Qur'an);
19. Choncho waonongeka!
Adakonza bwanji (Poinyoza
Qur'an)!
20. Ndiponso
waonongeka! Adakonza bwanji
(Poinyoza Qur'an)!
21. Kenako
adayang'anayang'ana (Nkhope za
anthu).
22. Kenakonso adachita tsinya
Ndikukwinya nkhope (kwambiri
Ndi mkwiyo).
23. Kenakonso adanyoza
Choonadi ndi kudzikweza
(Posachivomereza),
®\te*k&%%ty%
&K#W$i
©j£===CM»b^.>ijto
Surat 74. Al-Muddaththir Juzu 29 1291 T ^ *>i
vt yjdiSj^-
24. Adati: "Sichina ichi
(Qur'an) koma Ndi matsenga
amene adalandiridwa (Kuchokera
kwa amatsenga akale),
25. Sichina ichi koma ndi mawu
aanthu!"
26. Posachedwa ndimlowetsa
ku 'Saqara'
27. Nanga ndi chiyani
chakudziwitsa Za 'Saqara'?
28. (Ndi moto umene) susiya
(mnofu) Ndiponso susiya (fupa),
29. Umapsereza ndi kudetsa
khungu.
30. Kumeneko kuli khumi ndi
asanu Ndi anayi (alonda
oyang'anira Motowo.)
31. Ndipo sitidaike oyang'anira
kumoto (Kukhala anthu) koma
angelo; Ndipo sitidaike
chiwerengero chawo Koma
ndimayeso kwa amene
Sadakhulupirire, ndi kuti
atsimikize Amene adapatsidwa
mabuku (zimene Qur'an ikunena
za chiwerengero cha Angelo
akumoto) ndiponso kuti
Chionjezeke chikhulupiriro kwa
amene Akhulupirira, ndikuti
asapeneke Amene adapatsidwa
mabuku pamodzi Ndi okhulupirira.
Ndiponso kuti amene m'mitima
Mwawo muli matenda (matenda
Sfirat 74. AI-Muddaththir Juzu 29
1292 ™*j*-i
Vi jJjAtoj^-.
Achinyengo) komanso
osakhulupirira Anene: "Kodi
Mulungu akulinganji pa Fanizo
limeneli?" Momwemo Mulungu
Akumulekerera kusokera amene
Wamfuna, ndipo akumuongola
amene Wamfuna ndipo palibe
amene angadziwe Magulu a
nkhondo a Mbuye wako Kupatula
lye mwini.(Kutchula moto ndi
Zam'kati mwake) sichina koma
Ndichenjezo kwa anthu.
32. Sichoncho; ndikulumbirira
mwezi,
33. Ndi usiku pamene
ukuchoka,
34. Ndi m'bandakucha pamene
Kukuwala.
35. Ndithu uwo, (moto wa
Jahannama) ndi Chimodzi mwa
malodza aakulu,
36. Ndi chenjezo kwa anthu,
37. Kwa yemwe wafuna mwa
inu Kutsogola (pochita zabwino
Zokamthandiza tsiku louka kwa
Akufa) kapena kutsalira (ndi
Zam'dziko).
38. Mzimu uliwonse ukakhala
chikole Ndi zimene udachita.
39. Kupatula akudzanja lamanja
(Asilamu Amene adadzimasula
okha Potembenukira kwa Mulungu).
*-<&&
®PcJs\
Surat 74. AHVIuddaththir Juzu 29 1293 t * *>»
Vi yjdUj^
40. (I wo) adzakhala m'minda
(yosasimbika Kukongola kwake)
akufunsana wina ndi Mnzake;
41. Za anthu oipa,
42. (Kuti): "Nchiyani
chakulowetsani Kumoto?"
43. Adzanena: "Sitidali m'gulu
la Omwe adali kupemphera
(Swala)
44. Ndiponso sitidali
kuwadyetsa Masikini.
45. Koma tinkangomira
(m'zachabe ndi Zabodza) pamodzi
ndi omira M'menemo
46. Ndiponso tidali kukana za
tsiku la Malipiro
47. Mpaka imfa idatifika."
48. Siwudzawathandiza
uwomboli wa Awomboli.
49. Kodi ali ndi chiyani iwo
pakuti Azinyozera chenjezoli
(limene lili Qur'an?)
50. (Akuyenda mothamanga
kuti asamve Chenjezoli) ngati kuti
iwo ndi Mbidzi zothawa,
51. (Zimene) zathawa mkango.
52. Ati akufuna aliyense mwa
iwo Apatsidwe kalata
zotambasulidwa (Zimene
zitsimikize uthenga wa Mneneri
Muhammad{SAW});
k^m^o,
®Q&X\&&£\H
k.&Ll\L&?4&
®,
'•T> > -^>
*&$\'rj&&
Surat 74. Al-Muddaththir Juzu 29 1294 t S * j*-»
v t >di 3jj-
53. Sichoncho! Koma kuti iwo
Sakuopa tsiku lomaliza.
54. Sichoncho! Ndithu, ichi
(Qur'an) Ndichikumbutso
(chokwanira);
55. Amene wafuna
achikumbukire (Amene sakufuna
ndizake)!
56. Ndipo sangakumbukire
pokhapokha Mulungu atafuna. lye
ndiye Amene Ali woyenera
kumuopa, ndiponso Ndiye Mwini
kukhululukira (Amene akumuopa).
Surat 75. Al-Qiyamah Juzu 29
1295
Y**j*-»
V© JUUii ojj--
Surayi ikufotokoza zakuuka kwa anthu kuchokera kwa akufa
ndi kuweruzidwa pa zochita zawo. Ndiponso ikufotokoza za
tsiku la chimaliziro ndi zoopsa zake ndi kumuuza Mtumiki
(SAW) kuti Qur'an idzasonkhanitsidwa pa chifuwa chake.
Yadzudzula kwabasi amene akukonda kwambiri moyo
wadziko ndikusalabadira za moyo wa tsiku lomaliza. Ndipo
yafotokoza mmene zidzakhalire nkhope za okhulupirira ndi
nkhope za okanira. Yakambanso za madandaulo amene munthu
amakhala nawo imfa ikamfikira chifukwa chosakwaniritsa
zimene Mulungu adamlamula.
Ndipo surayi yamaliza ndi kutizindikiritsa kuti munthu
adzauka ku imfa tsiku lomaliza.
Surat 75. Al-Qiyamah Juzu 29 1296 * * *>»
Vo 3^Ufl]l 5j_^»
Surat Al-Qiyamat LXXV
w
$^Wr?
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Ndikulumbirira tsiku
lachimaliziro.
2. Ndikulumbiriranso mzimu
Wodzidzudzula (pa cholakwa
Chimene wachita. Ndithu,
Mudzaukitsidwa; mafupa anu
Omwazikana atasonkhanitsidwa.)
3. Kodi munthu akuganiza kuti
Ife (Amene tidamlenga kuchokera
Popanda chilichonse) sitidzatha
Kusonkhanitsa mafupa ake
(ofumbwa)?
4. Iyayi, Ife tikhoza
(kutisonkhanitsa) Ndi
kutilongosola bwino timizere
Takunsonga kwa zala zake.
(Mafupa Ake ndiye osanena)!
5. Koma munthu akukanira
(kuukaku) Ncholinga chopitiriza
kuchita zoipa M'masiku omwe
akudza mtsogolo Mwa moyo wake
onse.
6. Akufunsa (mwa chipongwe):
"Kodi Lidzakhala liti tsiku la
chimaliziro?"
7. Pamene maso adzangoti
tong'oo (Ndi mantha),
0M3\^3\^J^r
-2>
&<X\'J>$^i\%£#
©*y»j£t$<j£4
&^\&\i$
Surat 75. Al-Qiyamah Juzu 29 1297 t ^ *>» V* i*UJi 5^
8. Ndi kuchoka kuwala kwa
mwezi,
9. Ndipo dzuwa ndi mwezi
Ndikusonkhanitsidwa.
10. Munthu adzanena tsiku
limenelo: "Nkuti kothawira
(chilangochi?)"
11. (Adzauzidwa): "Iyayi, (iwe
munthu) Palibe pothawira (pako)!"
12. Tsiku limenelo kobwerera
(anthu) ndi Kwa Mbuye wako basi.
13. Tsiku limenelo munthu
adzauzidwa Zochita zake zimene
adazitsogoza Ndi zimene
adazichedwetsa.
14. Koma munthu adzadzichitira
umboni Yekha pa mzimu wake,
15. Ngakhale atapereka
madandaulo ake (Otani kuti
apulumuke nawo Sadzapulumuka).
16. Usaigwedezere (Qur'an)
lirime lako (Pamene
ikuvumbulutsidwa) kuti
Muifulumirire (kuiwerenga ndi
kuisunga Mumtima).
17. Ndithu, ndiudindo Wathu
Kuisonkhanitsa (mumtima mwako)
Ndi kukhazikitsa kawerengedwe
Kake (palirime lako).
18. Pamene tikukuwerengera
iwe Tsatira kuwerenga kwakeko
(Uku uli chetee).
iSZl ' U 9 t S ( *9*
%W&kZ&&&
eVtim%$\%
Surat 75, Al-Qiyamah Juzu 29 1298 * * *>» V © butt a^
19. Kenako, ndithu, ndiudindo
Wathu Kulongosola (zimene
sukumvetsa),
20. Iyayi koma mukukonda
moyo Wapadziko.
21. Ndipo mukusiya moyo wa
Tsiku lomaliza.
22. Nkhope zina tsiku limenelo
Zizawala kwambiri (ndi Mtendere),
23. Zili kumuyang'ana Mbuye
wawo
24. Ndipo nkhope zina tsiku
limenelo Zidzakhala zoziya.
25. Zikuyembekezeka kuti
zilandira Tsoka lodula msana.
26. Sichoncho! Pamene mzimu
udzafika Pa nthitimtima, (pomwe
pakumana Mafupa am'mapewa).
27. Ndipo ndikunenedwa ndani
Angamchiritse
28. Ndipo (iye mwini wake),
nkutsimikiza Kuti ndithu uku
ndikusiyana (ndi dziko Lapansi)
29. Ndipo miyendo
idzasanjikizana; (Iyi ndi nthawi
yochoka mzimu).
30. Tsiku limenelo koperekedwa
(anthu Onse) nkwa Mbuye wako;
31. Ndipo sadakhulupirire
komanso Sadapemphere swala
(zisanu),
«>fc©L£&£
!ffl*ai&tftf*^
&$&%>&
©a^i^is^
Surat 75. AI-Qiyamah Juzu 29 1299 Y * *>■! Vo &\Jti\ ©j^-
32. Koma (m'malo mwake)
adatsutsa ndi Kunyoza.
33. Kenaka adapita kubanja
lake (Uku akuyenda) monyada.
34. Kuonongeka nkwako (iwe
wotsutsa)! Kuonongeka zedi!
35. Ndiponso kuonongeka
Nkwako! kuonongeka zedi!
36. Kodi munthu akuganiza kuti
angosiidwa Chabe?
(Sadzaweruzidwa)?
37. Kodi sadali dontho la
umuna Umene udafwamphuka
(M'chiberekero)?
38. Kenako adakhala nthinthi
(Ntchintchi) ya magazi, ndipo
Adamlenga ndi kumlinganiza
(monga Munthu),
39. Ndipo adalenga kuchokera
mmenemo (M'magazi) omwewo
mitundu iwiri: Mwamuna ndi
mkazi.
40. Kodi (lye amene
adayambitsa Chilengedwe
choyambachi) sangathe Kuwapatsa
moyo akufa?
Surat 76. Al-Insan Juzu 29 1300 * * >>' V'l Ouj^i 3j^
M'surayi muli mawu olongosola chiyambi cha kalengedwe
ka munthu ndi kuti zili kwa munthu kuyamika Mulungu kapena
kumkana.
Yafotokoza mwachidule mphoto za okana. Ndipo yafotokoza
motambasula za mtendere wa Mulungu umene akaupereka kwa
anthu Ake okhulupirira.
Kenako yamulamula Mneneri (SAW) ndi kumfotokozera
chisomo chili pa iye pomvumbulutsira Qur'an yolemekezeka.
Ndipo yamulamula kupirira ndi kupitiriza kumvera.
Amene akukonda kwambiri moyo wa dziko lapansi ndi
kusiya moyo wa tsiku lomaliza yawachenjeza. Ndipo
yafotokozanso kuti mma aya amenewa muli maphunziro ndi
kuti palibe amene angapindule ndi maaya amenewa koma
kupyolera mchifuniro cha Mulungu.
Siirat 76. Al-Insan Juzu 29 I 1301 I * * *>■*
VI OUJ^I Sj^-
SuratALIns&n LXXVI
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambih, Wachisoni
1. Ndithu, munthu idampita
nthawi Yaitali kwambiri
(asanauziridwe Mzimu) pomwe
sadali chinthu Chotchulidwa.
2. Ndithu, Ife tamlenga munthu
kuchokera Kumbewu ya umunthu
yosanganikirana (Ya mkazi ndi ya
mwamuna) kuti Timuyese mayeso
(ndi malamulo Athu); Choncho
tidampanga kukhala wakumva Ndi
wopenya; (amve mawu a
Mulungu) Ndi kuti aone zisonyezo
Zake).
3. Ife tidamlongosolera njira
yoongoka: Kukhala wokhulupirira
kapena wotsutsa (Zonse zili kwa
iye).
4. Ndithu, Ife okana
tawakonzera unyolo
(Wam'miyendo yawo) ndi magoli
(Am'manja ndi m'makosi awo) ndi
Moto waukali woyaka.
5. Ndithu, oona pa
chikhulupiriro chawo Adzamwa
vinyo, chosanganizira chake
Chidzakhala (madzi a) kaafura.
6. (Kaafura ameneyo)
ndikasupe amene Azikamwapo
^«W*
-^
Surat 76. Al-Insan Juzu 29 1302~~| * * ^
vn ol-j^ioj^
akapolo a Mulungu ndi
Kumtulutsa (paliponse pamene
afuna) Kumtulutsa mofewa.
7. (Amene) akukwaniritsa
zimene adalonjeza (Okha kwa
Mulungu), ndiponso Akuopa tsiku
(lalikulu) limene Zoipa zake
zidzakhala zofalikira Ponseponse.
8. Ndipo amadyetsa chakudya
masikini, Amasiye ndi ogwidwa pa
nkhondo, Pomwe iwo
akuchifunanso.
9. Amanena (chamumtima
akamapereka Chakudyacho):
"Tikukudyetsani Chifukwa
chofuna chikondi cha Mulungu
basi; sitikufuna kwa inu Malipiro
kapena kuthokoza.
10. Ndithu, ife tikuopa kwa
Mbuye wathu Tsiku lokhwinyata
nkhope ndi mavuto Aakulu."
11. Ndipo Mulungu
adzawateteza Kumavuto a tsiku
limenelo ndiponso Adzawapatsa
Mtendere ndi chisangalalo.
12. Ndipo adzawalipira
chifukwa cha kupirira Kwawo
munda wa mtendere ndi Nsalu
zaveleveti;
13. Atatsamira m'menemo
pamabedi (Amtengo wapatali);
sazamva M'menemo kutentha kwa
dzuwa Kapena kuzizira.
+* \c
e$J£&JP&%>&&&%\
bl l#» '"CAS"' l* >f' t" fj i "
Surat 76. Al-Insan Juzu 29 I 1303 I t <\ *j*-i
VI OUJ^t 5 J>( -
14. Mithunzi yake
ikawayandikira iwo Ndipo mikoko
yazipatso idzatewa Pafupi (moti
munthu atha kuthyola Ali
chigonere).
15. Ndipo adzakhala
akuzunguliridwa (Ndi otumikira)
uku atatenga zomwera Zasiliva ndi
matambula onyezimira Ndiponso
olangala.
16. Zolangala zopangidwa ku
siliva, atalinga Bwino zakumwazo
(malinga ndi kufuna Kwawo).
17. Ndipo (anthu abwino)
akamwetsedwa Kumeneko vinyo,
chosakanizira chake Chikafanana
ndi zanjabila (chikasu).
18. M'menemo muli kasupe
wotchedwa Salisabila,
19. Ndipo azikawazungulira
anyamata Osasinthika
(chilengedwe chawo,) Utawaona
(chifiikwa cha kukongola Kwawo
ndi kuwala kwa nkhope zawo)
Ungawaganizire kuti ndi ngale
Zomwazidwa.
20. Ndipo ukadzaona kumeneko
(ku Jannah) ukaona mtendere ndi
ufumu Waukulu.
21. Pamwamba pawo
padzakhala nsalu Zaveleveti
zopyapyala, zobiriwira Ndi nsalu
zaveleveti zochindikala,
))\,9 ,'£ 9'\'y
dj/j£&>
\* 9 '/A' 9 *'*--* *• 9 T \"\'i
m^^\y^^^^
J^j^k^j}^ &jffi\$*5
®]%&V\j&
Surat 76. Al-Insan Juzu 29
1304 Tl*>i
V\ OUJ^I 5jj^
Akavekedwa m'manja mwawo
zibangiri Zasiliva; Mbuye wawo
akawamwetsa Chakumwa china
choyera kwambiri.
22. (Akawauza kuti:) "Ndithu
iyi ndi mphoto Yanu ndipo ntchito
Zanu ndi zolandiridwa."
23. Ndithu, Ife taivumbulutsa
kwa iwe Qur'an
mwapang'onopang'ono (kuti
Uisunge bwino, usaiwale)
24. Choncho, pirira ndi lamulo
la Mbuye Wako ndipo usamvere
wamachimo Kapena wokanira
Aliyense mwa iwo.
25. Ndipo kumbukira dzina la
Mbuye Wako; mmawa, ndi
madzulo (swala za Subuhi, Zuhri
ndi Asri).
26. Ndipo usiku mlambire lye,
(swala YaMagharib ndi Isha);
ndiponso Umulemekeze usiku
nthawi yaitali (Popemphera sunna
za tahajudi)
27. Ndithu awa akukonda
umoyo Wadziko lapansi, ndipo
akulisiya Kumbuyo tsiku lovuta.
28. Ife ndi amene tidawalenga
ndipo Tidalimbika kalengedwe
kawo; ndipo Titafuna
tingabweretse ena onga iwo
(Omvera Mulungu) kulowa
m'malo Mwawo.
%&Gtrfe%&\&&
k\**r?4
®%&uX$\®&&&<>%\
8Wtt#4p>a#6
i<\ 'r. 9 * '"ft' 9 "i <.' ?> S ZX' 9 >'\
Surat 76. Al-Insan Juzu 29
1305
M >>»
VI OUJ^I 6jj~>
29. Ndithu ichi ndichikumbutso
Choncho amene Afuna atsata njira
yopitira kwa Mbuye wake
(pomukhulupirira ndi
Kumumvera).
30. Koma simungafune nokha
chilichonse Pokhapokha atafuna
Mulungu, ndithu Mulungu ndi
Wodziwa, Wanzeru.
31. Akumlowetsa amene
wamfuna Kuchifundo Chake;
koma oyipa Wawalinganizira
chilango chowawa Kwambiri.
Surat 77. Al-Mursalat Juzu 29 I 1306 I t * *>H VV o*-jI» 5j>-
Mfundo yofiinika imene surayi ikufotokoza ndi kuuka ku
imfa pa tsiku la Kiyama. Ndipo ikupereka kwa anthu zizindikiro
zosonyeza kuti zimenezo zidzachitika pakuti Mulungu adachita
zazikulu kuposa zimenezo.
Mawu akuti: "Kuwonongeka kwakukulu tsiku limenelo kuli
pa otsutsa"abwerezedwabwerezedwa kokwanira khumi pofuna
kuwaopseza ndi kuwachenjeza amene akukana zakuuka
kuchokera ku imfa, ndi kuti adzakumana nacho chilango
chachikulu patsikulo.
Kenako ikuuza anthu olungama nkhani yabwino ponena kuti
mtendere ndi chisangalalalo cha Mulungu zidzakhala pa iwo.
Ndipo surayi yamaliza ndi kunenetsa kuti kuonongeka kuli pa
okana Mulungu amenenso sakhulupirira Qur'an.
Surat 77. Al-Mursalat Juzu 29 1307 Y * tjA-i VV o^UjLi 5^
S«ra* Al-Mursalat LXXVII
M
mm&
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Ndikulumbirira mphepo
yomwe Ikuomba motsatizana.
2. Ndi mphepo yamkuntho.
3. Ndi mphepo yobalalitsa
mitambo ndi Mvula.
4. Ndi ma aya osiyanitsa Pakati
pachoona ndi chonama;
5. Ndi angelo opereka
chivumbulutso Kwa aneneri.
6. Kuti chichotse madandaulo
ndiponso Kuti chikhale chenjezo;
7. Ndithu, zimene
mukulonjezedwa (kuti Chimaliziro
chidzakhalapo) Zidzachitikadi
(popanda chipeneko),
8. Pamene nyenyezi
zidzafafanizidwa (Kuwala kwake
ndi kuchotsedwa M'malo mwake).
9. Ndiponso pamene thambo
Lidzang'ambidwa.
10. Ndi pamenenso mapiri
adzachotsedwa M'malo mwake
ndi kuperedwa (Kukhala fumbi).
11. Ndi pamene aneneri
adzasonkhanitsidwa Pa nthawi
Q^lfc^J)!^
-Ci
©tti^cJ^J^l'S
<teaa»
Surat 77. AI-Mursalat Juzu 29 I 1308 I T * *>i VV o*-^ 5jj-
yake, (kuti apereke umboni
Kumibadwo yawo).
12. Kodi nditsiku lanji
adzichedwetsera (zinthu
Zikuluzikulu kuti zizachitike).
13. Nditsiku la chiweruziro
(pakati Pa zolengedwa).
14. Nchiyani chakudziwitsa za
tsiku la Chiweruzirolo.?
15. Kuonongeka kwakukulu
tsiku limenelo Kuli pa otsutsa
(lonjezo Lathu la Kuuka ku imfa)
16. Kodi sitidawaononge
(anthu) akale (Chifukwa cha
machimo awo, monga Anthu a
Nuhu, Adi ndi Samudu)?
17. Kenako titsatiza ena (okana
Mulungu m'kuonongekako monga
Tidawachitira oyamba),
18. Chomwecho tiwachitiranso
Ochimwa.
19. Kuonongeka kwakukulu
tsiku Limenelo kuli pa otsutsa
(Lonjezo Lathu lakuuka ku imfa).
20. Kodi sitidakulengeni
kuchokera Kumadzi onyozeka,
(madzi ambewu ya Munthu)?
21. Kenako tidawaika pamalo
Okhazikika (kuti chilengedwe
chake Chikwanire pamenepo),
22. Mpaka nyengo yodziwika
(imene Tidaipima kuti mwana
abadwe).
' 9 -lift J A* l>* s*u
Siirat 77. Al-Mursalat Juzu 29 1309 Y a ^j*-i VV 0*^1 5^
23. Tidaipima nyengoyo;
taonani Kupima bwino Ife opima!
24. Kuonongeka kwakukulu
tsiku Limenelo kuli pa otsutsa
(Lonjezo Lathu lakuuka ku imfa).
25. Kodi sitidaichite nthaka
kukhala Yofungatira,
26. Amoyo ndi akufa?
27. Ndipo tidaika m'menemo
mapiri Ataliatali (olimbitsa
nthaka), Ndipo takumwetsani
madzi okoma.
28. Kuonongeka kwakukulu
tsiku Limenelo kuli pa otsutsa
(Mtendere umenewu).
29. (Kudzanenedwa kwa okana
tsiku la Chimaliziro:) Pitani
kuzimene Mudali kuzitsutsa zija.
30. Pitani kumthunzi (wautsi wa
Kumoto) wa nthambi zitatu,
31. Simthunzi (wamtendere)
ndiponso Siwotchinjiriza
kumalawi a moto."
32. Ndithu uwo (moto
umenewu) umaponya Mphalikira
(mbaliwali) zazikulu ngati Nyumba,
33. Zonga ngati ngamira
zachikasu.
34. Kuonongeka kwakukulu
tsiku limenelo Kuli pa otsutsa
(zimenezi).
s* • f^Tt \ ' 9 t$\ 9 '
Surat 77. Al-Mursalat Juzu 29 1310 Y H *>i VV o^>i Sj^
35. Hi ndi tsiku lomwe
Sadzalankhula.
36. Ndipo sadzapatsidwa
chilolezo (Choyankhulira) kuti
apereke madandaulo Awo.
37. Kuonongeka kwakukulu
tsiku Limenelo kuli pa otsutsa (za
Tsiku limenelo).
38. (Adzauzidwa kuti): Hi ndi
tsiku loweruza (Pakati pa abwino
ndi oipa Takusonkhanitsani inu
(otsutsa Muhammad {SAW}), ndi
akale (otsutsa aneneri akale).
39. Ngati muli ndi ndale
(yodzipulumutsira Kuchilango
Changa) ndichiteni ndaleyo!
40. Kuonongeka kwakukulu
tsiku limenelo kuli Pa otsutsa
(lonjezo la Mulungu).
41. Ndithu, oopa (Mulungu
tsiku limenelo) Adzakhala
mumthunzi ndi M'mitsinje,
42. Ndipo adzakhala ndi zipatso
zomwe Azidzazifuna.
43. (Kudzanenedwa kwa iwo):
"Idyani, Imwani mokondwa
chifukwa cha Zabwino zomwe
mudali kuchita (Muumoyo wa
dziko lapansi).
44. Ndithu umo ndi mmene Ife
timawalipirira Ochita zabwino.
©Q^^irA^
^^^&^^yf^
^^%a^(S
^JcM&^Ot
&~&^^™ A
Surat 77. Al-Mursalat Juzu 29 1 1311 | Y ^ tji-i VV o^L-^li Sj^-
45. Kuonongeka kwakukulu
Tsiku limenelo kuli pa Otsutsa
(mtendere wa Mulungu)
46. Idyani, sangalalani
pang'ono M'kanthawi kochepa;
ndithu, Inu ndinu ochimwa
(chifukwa Chakumphatikiza
Mulungu ndi Zolengedwa).
47. Kuonongeka kwakukulu
tsiku Limenelo kuli pa otsutsa
(Mtendere wa Mulungu).
48. Ndipo kukanenedwa kwa
iwo: "Weramani, (pembedzani
Mulungu)" Sakuwerama.
49. Kuonongeka kwakukulu
tsiku Limenelo kuli pa otsutsa
(Malamulo a Mulungu).
50. Kodi ndi nkhani iti imene
Adzaikhulupirira pambuyo pa Iyi
(Qur'an)?
tftff *9&L9\9'
%^m^-&
Surat 78. An-Naba> Juzu 30
1312
*>«
VA
5 J>"
^^
r Lr\Jr=2;^>^~»^ ^^ r
SURAT AN-NABA' LXXVIII
Surayi yanenetsa zakuuka m'manda, ndipo yaopseza amene
akukaikira zimenezi. Ndiponso yasonyeza kutheka kwa
zimenezo posonyeza zinthu zomwe zikuonetsa mphamvu za
Mulungu. Ndipo yatsimikiza za kuukako potchula zina mwa
zisonyezo zake. Kenako yatchula mabwerero a anthu oipa,
opyola malire. Ndi mabwerero a anthu abwino, oopa Mulungu.
Ndipo yamalizira ndikuchenjeza za tsiku loopsalo.
Surat An-Naba ' LXXVIII
m
0^\^\&\*r
-&
®v&Z&
A
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Kodi akufunsana zachiyani?
2. Za nkhani yayikulu ija.
3. Imene iwo akusiyana
(maganizo). 1
4. Aleke (zimenezo) adzadziwa
posachedwapa. 2
5. Ayi, ndithu, aleke
(zimenezo); Posachedwapa
adzadziwa zoona Zake (pamene
chilango chidzawatsikira) 3
1 Nkhani yaikulu imene akafiri (anthu osakhulupirira Mulungu) adali kufunsana
wina ndi mnzake ndi nkhani yakuuka tsiku la Kiyama t ndi uneneri wa Mtumiki
Muhammad. Amafunsana kuti, "Kodi nzoona tidzadzuka m'manda, nanga
nzoona kuti Muhammad ndi Mneneri?" Adali kufunsananso kuti, "Kodi zakuti
Mulungu ndi Mmodzi ndi zoona?"
2 Kulankhula koti: "Kallaa" kwanenedwa kwambiri m'Qur'an. Tanthauzo lake
nthawi zina ndikuletsa, nthawi zina ndikutsimikiza. Choncho mawuwa
amatanthauzidwa malinga ndi momwe chiganizocho chilili.
3 Mulungu, apa, akuwauza kuti asiye kuganizira zinthu zopanda pake. Kodi
sadadziwebe mpaka tsopano kuti Muhammad ndi Mneneri wa Mulungu,
®&&&&P
Surat 78. An-Naba' Juzu 30 1313 r • *>
VA l_Jl 3^
6. Kodi sitidachite nthaka
kukhalaNgati choyala? 1
7. Ndi mapiri ngati zichiri
(zolimbitsa Nthaka)?
8. Ndipo takulengani mitundu
iwiri (Amuna ndi akazi).
9. Ndipo tidachita tulo tanu
kukhala Mpumulo (kumavuto a
ntchito).
10. Ndipo taupanga usiku
kukhala ngati Chovala
(pokuvindikirani Ndi mdima
wake).
11. Ndipo tapanga masana
kukhala Nthawi yopezera zofunika
pa moyo;
12. Ndipo tamanga pamwamba
panu thambo Zisanu ndi ziwiri
zolimba;
13. Ndipo tidapanga nyali
yowala ndi Yotentha kwambiri
(dzuwa);
14. Ndipo tawatsitsa madzi
otsika Mwamphamvu kuchokera
*«lft&3SE3
£ 1183*0%
to®zaqm%
••<,
m<>j$&$& i s&
©V>t£ j>l£ i^H^Xi>5
^sW6^^a»^$ts
ndikuti Mulungu ndi Mmodzi yekha? Ndikutinso kuli tsiku lomaliza; pamene
munthu aliyense adzalipidwa pazimene adachita? Basi tsiku lomaliza
likadzawafikira adzadziwa kuti zimene adali kuwauza Mneneri nzoona.
1 Kuyambira aya iyi, kudzafika aya 16, Mulungu akusonyeza anthu Ake
madalitso ambiri omwe wawadalitsa nawo kuti azindikire kuti Mwini kupereka
madalitso amenewa m'dziko sangawasiye anthu Ake m'kusokera popanda
kuwatumizira munthu wowaongolera kunjira yabwino, ndikuwadziwitsa
zamtendere wapadziko ndi tsiku lomaliza. Ndikuti Mulungu amene adapanga
zonsezi palibe chimene angachilephere. Ndipo tanthauzo la choyala, apa, ndi
pamalo poti nkutheka munthu kuchita chimene akufuna pa moyo wake.
Tanthauzo lake sikuti dothi lakhala ngati mkeka wa pabedi ayi.
Surat 78. An-Naba' Juzu 30
1314
'J*
VA
0j^
ku mitambo, Ya mvula;
15. Kuti titulutse ndi madziwo
mbewu Ndi m'mera, (chomwe ndi
chakudya Cha anthu ndi nyama).
16. Ndi minda yothothana
nthambi za Mitengo.
17. Ndithu, tsiku la chiweruzo
ndi Nthawi imene
idakhazikitsidwa kale,
18. Tsiku limene lipenga
(lakuuka) Lidzaimbidwa ndipo inu
mudzabwera (Kubwalo
losonkhanirana) muli
Magulumagulu.
19. Ndipo thambo
lidzatsegulidwa (Mbali zonse):
lidzakhala Makomomakomo.
20. Ndipo mapiri
adzachotsedwa m'malo Mwake,
adzakhala ngati zideruderu. 1
21. Ndithu, moto wa Jahena
ukuwadikirira (Oipa).
22. Mbuto ya opyola malire.
m&ur&
©\SUJf<
$ t* i'*\ " 9 -K'< 9t
Z<Z > '9 4
SW^^d*^
1 Apa, ndikuti zimene munthu amaziona patsogolo pake nkumaziganizira ngati
madzi pomwe sali madzi. Choncho pa tsiku limenelo mapiri adzaoneka ngati
akhazikika monga m'mene adalili pomwe sichoncho, adzakhala ngati thonje
louluka ndi mphepo.
2 Jahannamu ndi dzina lamoto wodziwika wa tsiku lomaliza. Apa Mulungu
akutidziwitsa kuti Jahannamu ndi malo amene akudikira akafiri kuti
m'menemo akalipidwe malipiro awo chifukwa chokanira aneneri pambuyo
powasonyeza ztzindikiro zoti iwo ndi aneneri a Mulungu. Ndiponso
kumulakwira Mulungu pochita zimene adaletsa monga; kukana umodzi wa
Mulungu, kukana utumiki wa Mahammad (SAW) ndi kukana uthenga wa
Qur'an. Komanso kugwa mmachimo osiyanasiyana.
Surat 78. An-Naba' Juzu 30 1315 T * *>i
VA i — -all 9jy*
23. Adzakhala m'menemo
muyaya.
24. Sadzalawa m'menemo
kuzizira (Kowachotsera kutentha),
kapena Chakumwa (chowachotsera
ludzu lawo);
25. Kupatula madzi otentha
Kwambiri ndi mafinya (otuluka
Mmatupi a anthu a kumoto);
26. Kukhala malipiro olingana
Ndi ntchito zawo.
27. Ndithu iwo sadali
kuyembekezera Chiwerengero (cha
Mulungu);
28. Adatsutsa zizindikiro Zathu
(Zosonyeza kuuka kwa akufa) ndi
Mtsutso waukulu.
29. Ndipo chinthu chilichonse
Tachisunga mochilemba.
30. Basi, lawani (lero chilango
Changa); Sitikuonjezerani chinthu
China koma chilango pamwamba
pa Chilango.
31. Ndithu, anthu oopa
Mulungu adzakhala Ndi malo
wopambana.
32. Minda ndi zipatso za mphesa.
33. Ndi mabuthu (anamwali)
Ofanana misinkhu.
34. Ndi zipanda zodzaza Ndi
zakumwa.
Sfirat 78. An-Naba' Juzu 30
1316
r* *>i
VA I— dl oj^
35. Sakamva m'menemo mawu
opanda Pake kapena bodza.
36. Amenewa ndi malipiro
Ochokera kwa Mbuye wako
Zopereka zokwanira. 1
37. Mbuye wa kumwamba ndi
pansi Ndi zimene zili pakati pake;
Wa Chifundo Chambiri. Palibe
amene adzakhala ndi Mphamvu
yolankhulana naye (Pa tsiku
limenero);
38. Tsiku limene adzaima Jibril
Ndi angelo pa mzere (ali
Odzichepetsa); sadzalankhula
Aliyense mwa iwo kupatula
Yekhayo amene adzaloledwa ndi
Wachifundo Chambiri
(kulankhula) Ndipo adzanena
zolondola.
39. Limenelo ndi tsiku loona,
(Lopanda chikaiko); choncho
Amene akufuna adzipezere Malo
(njira yonkera) Kwa Mbuye wake.
(Pomugonjera lye pa umoyo uno
wadziko lapansi).
40. Ndithu, tikukuchenjezani
Zachilango chomwe chili pafupi
i'*<^'\1t'*i '^'''v
hZm$&^££Z3
h%\^$&Q0&i
l>
®0^»J\|j
JtfiS&^^jJl^
'j&tew$s®&i
Chipembedzo cha Chisilamu chikuphunzitsa kuti pali zisangalalo ziwiri:
Chisangalalo cha mzimu ndi chisangalalo cha thupi. Tsono chisangalalo cha
mzimu ndiko kuyanjana kochokera kwa Mulungu kumene anthu Ake abwino
adzakupeza. Chisangalalo cha thupi ndi monga m'mene afotokozera mu ayah
iyi ndi msura zina: Zokondweretsa monga minda, akazi okongola, mowa
(osaledzeretsa) ndiponso sikudzakhala kumva chilichonse chokhumudwitsa.
Taonani, zoledzeretsa ndi zoletsedwa padziko lino lapansi chifukwa cha zoipa
zake. Koma zoledzeretsa za patsiku la Kiyama zidzakhala zopanda zoipa.
Surat 79. An-Nazi'at Juzu 30 1317 T * *>-» V* oIpjUi Sj^
Kudza; tsiku limene munthu
Adzayang'ana zimene adatsogoza
Manja ake, ndipo kafiri
(wosakhulupirira) Adzanena:
Kalanga ine! Ndikadakhala Dothi,
(kuti ndisalangidwe chilango
Chikundiy embekezachi) .
SURAT AN-NAZPAT LXXIX
Surayi yayamba ndikulumbira potsimikizira kuti kuli kuuka.
Ndipo yatsatiza nkhani ya Musa ndi Firiauna ndicholinga
chomtonthoza Mtumiki (SAW) kumavuto omwe ankakumana
nawo panjira yolalikira. Yatsatizanso kulongosola za zimene
zikuwayembekezera opyola malire ndi achinyengo pa tsiku
lomaliza. Ndipo yamalizira ndi funso la amushirikina lofunsa
zanthawi ya tsiku lomaliza ndikulongosola kuti ntchito ya
Mtumiki (SAW) ndi kuchenjeza omwe akuopa za tsikulo.
Koma iye sadziwapo kanthu za nthawi yakudza Qiyama.
Surat An-Nazi'at LXXIX
llff^^
'JL
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Ndikulumbirira (angelo)
Amene amazula (mizimu ya
Osakhulupirira) mwamphamvu. 1
Q
)^l^l^
^■^
&§j*<%Pj$j
(Ndime 1-5) M'Qur'an nthawi zambiri Mulungu amalumbirira zolengedwa
Zake; zamoyo ndi zopanda moyo, zooneka ndi zosaoneka. Cholinga
ndikutilimbikitsa kuti tikhale olingalira luso Lake pa chinthu chilichonse
chimene wachilumbirira kuti tizindikire ulemerero Wake ndi mphamvu Zake
zoposa.
Surat 79. An-Nazi'at Juzu 30
1318
V. *jJfc-» VH OlPjlJlSjj^
2. Ndikulumbiriranso (angelo)
Amene amachotsa (mizimu ya
Okhulupirira) moleza.
3. Ndi omwe amasambira (nayo
Mizimuyo) mumlengalenga (ponka
nayo ku malo ake Oyembekezera).
4. Ndi iwo amene akupikisana
Pokwaniritsa malamulo a
Mulungu.
5. Ndi iwo (angelo) amene
Akulongosola malamulo (Ake).
(Ndithudi inu anthu mudzauka
Kwa akufa).
6. Patsiku lomwe (lipenga
loyamba Lidzaimbidwa), dziko
lapansi ndi Mapiri ake
zidzagwedezeka (ndipo Aliyense
adzafa).
7. Ndipo kudzatsatira kuyimba
kwa Lipenga lachiwiri (kumene
Kudzaukitsa akufa onse).
8. Tsiku limenelo mitima
idzanjenjemera Ndi kuopa,
9. Maso a eni mitimayo
adzakhala Ozyolika (chifukwa
chamadandaulo);
10. (Osakhulupirira) akunena:
"Kodi nzoona tidzabwezedwa
Pambuyo pa imfa monga tidalili
kale?"
11. "Pomwe ife titakhala
mafupa Ofumbwa (tingabwezedwe
?' u in.'
^*a ' Hill '• 9 >£ '>'
t&$\\2&
©Aj^^U;W>\
mV\&£%3$>
&%j$U&M\'&
Surat 79. An-Nazi'at Juzu 30
1319
*j*
V^ OlPjldl dj>-
ndi Kuukitsidwa mwa tsopano)?"
12. Adanena (mokanira ndi
mwachipongwe): "Choncho
kubwerera kumeneko ngati
Kudzakhalepodi kudzakhala
kotaika (Ndi kopanda phindu kwa
ife. Pomwe Ife sindife oyenera
kutaika)"
13. (Musaganize kubwererako
nchinthu Chovuta). Ndithundithu
Kiyamayo ndi Nkuwo umodzi.
14. Mwadzidzidzi (zolengedwa
zonse) Zidzangoona zili padziko
Latsopano (zili zamoyo).
15. Kodi yakufika (iwe
Mtumiki) (SAW) Nkhani ya
Musa? 1
16. Pamene Mbuye wake
adamuitana pa Chigwa choyera
(chotchedwa) Tuwaa,
17. (Adamuuza kuti) pita kwa
Farawo Ndithu, iye wapyola
malire, (Mkudzitukumula kwake
ndikupondereza Anthu).
18. Umuuze kuti "Kodi ukufuna
Kudziyeretsa?"
19. "Ndikuti ndikuongolere kwa
Mbuye wako kuti uzimuopa?"
©*r^
&S3\V$$i
1 Kuyambira aya iyi mpaka aya 26 Ambuye Mulungu akumtonthoza mneneri
Wake pomuuza nkhani ya Mneneri Musa momwe Farawo adamkanira, ndikuti
asaganize kuti vutoli lampeza iye yekha koma kuti aneneri enanso akale
lidawaonekeranso. Ndiponso m'ma ayah amenewa muli chenjezo kwa akafiri
kuti aope Mulungu kuti asawalange monga adamulangira Farawo ndi anthu
ake amene adali kutsutsana ndi Mulungu.
Surat 79. An-Nazi'at Juzu 30 1320 T • *>i V* oipjUi 5jj~-
20. (Basi Musa) adamuonetsa
(Firiauna) chozizwitsa Chachikulu.
21. Koma (Firiauna) adatsutsa
(Musa Pazimene adadza nazo zija)
Ndi kunyoza.
22. Kenaka adabwerera uku
akulimbika Kutsutsana naye
(Mulungu),
23. Adawasonkhanitsa (afiti)
uku Akuitana anthu;
24. Nanena: "Ine ndine mbuye
wanu Wapamwambamwamba!"
25. Pamenepo Mulungu
adamulanga Chifukwa cha mawu
ake omaliza Ndi oyamba.
26. Ndithu, pa zimenezi pali
Phunziro (lalikulu) kwa yemwe
Akuopa Mulungu.
27. Kodi kulengedwa kwanu,
(inu Osakhulupirira kuti muuke)
Nkovuta kapena thambo limene
Adalimanga (posonkhanitsa Mbali
zake zosiyanasiyana Ndikukhala
chinthu chimodzi)? 1
28. Adatukula msinkhu wake
Ndikulikonza bwino (popanda
Pena pong'ambika kapena
Posiyana ndi pena).
29. Ndipo amavindikira mdima
mu usiku Wake ndipo amatulutsa
©Lfr>j^3 1$\£m» 7&J
Q&ffi'&id&b
1 Tanthauzo lake ndikuti "Kodi chilengedwe chanu nchovuta kwambiri kuposa
chilengedwe cha thambo pamene inu mukuganiza kuti Mulungu sangathe
kukudzutsani pambuyo pa imfa?"
Surat 79. An-Nazi'at Juzu 30 132 1 T • *>» V^ oIpjlJi 5jj~-
kuwala Mu usana wake.
30. Ndipo pambuyo
pazimenezo, Nthaka adaiyala (kuti
ikhale Yoyenera kuikhala).
31. Adatulutsa m'menemo
madzi Ake (potulutsa akasupe)
Ndikumeretsa msipu wake (kuti
Anthu ndi nyama azidya
msipuwo);
32. Ndipo mapiri
adawakhazikitsa
(Ndikuwalimbika);
33. (Adachita zonse izi)
chifukwa Chokusangalatsani inu
ndiZiwetozanu. 1
34. Choncho likadzafika tsoka
lalikulu (Tsiku la Kiyama).
35. Tsiku limenelo munthu
adzakumbukira Zimene adachita,
(zabwino ndi zoipa).
36. Ndipo moto waukali
udzawonetsedwa Kwa yense
openya.
37. Tsono amene adapyola
malire (Mmachimo ake),
38. Ndikudzisankhira (yekha)
Umoyo wapadziko lapansi,
39. Ndithu, Jahena ndiwo malo
ake (Palibe kwina).
©^po^JS 6J0 $3%
&
1 Mu aya iyi Mulungu akusonyeza kuti lye ndi Mwini mphamvu zonse zochitira
chinthu chilichonse chachikulu kuposa kuwaukitsa akufa; ndiponso akukumbutsa
ufulu Wake waukulu womwe adatichitira potipatsa zinthu zonsezo kuti
tithandizike nazo.
Surat 79. An-Nazi'at Juzu 30
1322 ?• *jk* V* ou-jUi Sj^-
40. Tsono amene akuopa kuti
adzaimirira Pamaso pa Mbuye
wake, nauletsa Mtima wake ku
zilakolako zoipa,
41. Ndithu, munda wa mtendere
ndiwo Adzakhale malo ake;
(palibenso Kwina).
42. Akukufunsa (iwe Mtumiki)
(SAW) Zanthawi (ya tsiku
lomaliza kuti) "Idzakhala liti?"
43. Uli ndi mphamvu yanji iwe
Yofotokozera tsiku la Kiyamalo?
(Iwe ulibe kuzindikira za nthawiyo
Kotero kuti ungaitchule kwa iwo).
44. Mbuye wako ndi amene ali
Ndikuzindikira kudza kwake.
45. Iwe (ntchito yako)
ndikuwachenjeza Amene akuiopa;
(osati kulengeza Zanthawi yake).
46. Tsiku limene adzaiona
adzakhala Ngati sadakhale
(padziko nthawi Yayitali), koma
ngati madzulo Amodzi kapena
masana ake (nthawi Ya m'mawa). 1
J28M d*$ iy$& 6&<^SIJ
1 Apa tanthauzo lake ndikuti adzaona masiku onse amene adakhala m'dziko
ngati lidali ola limodzi.
Surat 80. 'Abasa
Juzu 30
1323
*>■'
A * ^r-P oj>-»
SURAT 'ABASA LXXX
Surayi yayamba ndi kudzudzula Mneneri (SAW) pamene
adasonyeza kusamlabadira Ibn ummu Makutumi, pamene
adamdzera kudzafuna chiongoko ndi maphunziro. Pamenepo
nkuti Mneneri (SAW) atatanganidwa ndikulalikira akuluakulu
achiQuraish uku akuyembekezera kuti mwina angavomereze
ulaliki wake, ndikuti ngati iwo atero ndiye kuti anthu ambiri
omwe amatsatira adzavomerezanso. Kenako Surayi yakumbutsa
munthu zamtendere wa Mulungu umene uli paiye, kuyambira
pakubadwa kwake mpaka mapeto a moyo wake padziko lino.
Ndipo yamalizira kunena za tsiku la Kiyama polongosola kuti
patsikulo anthu adzakhala m'magulu awiri: Gulu la chimwemwe
la okhulupirira, ndi gulu loipa la okanira. (osakhulupirira).
Surat 'Abasa LXXX
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Adachita tsinya (Mneneri)
ndi Kuyang'ana kumbali. 1
2. Chifukwa chakuti adamdzera
Wakhungu (kudzamfunsa
Ojfe&\<&$\&\j
I "ClIJ
Tsiku lina Mneneri (SAW) atakhala ndi akuluakulu a Aquraishi. Adali
kuwalalikira za chipembedzo mwachidwi, ndipo adali kuyembekezera kuti
akavomereza Chisilamu iwo, ndiye kuti anthu owatsatira naonso avomereza.
Chifukwa anthu ambiri sadalowe Chisilamu poopa atsogoleri awo. Pa nthawi
imeneyi adatulukira wakhungu wina yemwe ankatchedwa Ibn Ummu Maktum.
Sadadziwe kuti Mneneri (SAW) ali wotanganidwa Adamukuwira u Ee! Iwe
Mneneri wa Mulungu! Ndiphunzitse inenso zimene wakuphunzitsa Mulungu."
Ndipo ankangomubwerezera bwerezera mawu amenewa. Mneneri (SAW)
pakuti adali ndi chidwi ndi kulalikira akuluakulu aja, Adamchitira tsinya
wakhungu uja chifukwa chomuonongera ntchito yake; Sadamumvere. Basi
pamenepa Mulungu akumdzudzula Mneneri Wake pa zomwe adachita posiya
kumumvera amene adamubwerera kudzafuna chiongoko.
Surat 80. 'Abasa Juzu 30
1324
*>'
A • j^-p 5jj-»
Zokhudzana ndi chipembedzo
Chake pamene iye adali
Kuyankhula ndi atsogoleri
AchiQuraishi).
3. Nanga chingakudziwitse
nchiyani kuti Mwina iye
angadziyeretse? (Pomvera ulaliki
wako Watsopano).
4. Kapena akumbukira, ndipo
Kukumbukirako kumthandiza?
5. Koma amene
wadzikwaniritsa (ndi Chuma chake
ndi mphamvu zake),
6. Ameneyo ndi yemwe
ukumchitira Chidwi.
7. Palibe chilichonse pa iwe
Ngati sadziyeretsa.
8. Koma amene wakudzera uku
Akuthamanga (kufuna Maphunziro
ndi chiongoko),
9. Ndipo iye akuopa (Mulungu
Mumtima mwake).
10. Za iye, iwe sukusamala,
(Ukuyikira chidwi kwa wina).
11. Sichoncho! Ndithudi iyi
(Qur'an) ndi chikumbutso
(Chenjezo). 1
afcW^MK
& Si&\\l"3gL&t'1
©,
W&&$$£\
0(jwiw|^ul
®&»£ 2 A^(^> \3il^
V It"?'
(Ndime 11-16) Apa Mulungu akumuletsa Mtumiki Wake kuti asachitenso
zonga adachitazo ndi kumuuza kuti Qur'an ndi ulaliki chabe, amene afuna
kulingalira za ulalikiwo, umuthandiza, ndipo amene safuna, kutaika ndi kwake.
Ndiponso adamufotokozera kuti Qur'an idachokera m'mabuku olemekezeka;
idachokera ku "Lauhil-Mahfudh" Mabuku omwe ali m'manja mwa Angelo
olemba, olemekezeka, ochita zabwino omwe ndi abwino kuposa Aquraishi.
Surat 80. < Abasa Juzu 30 1325 T * >>»
A* ir -fi 5j>*
12. Basi, amene wafuna
alangizika (Ndi Qur'an, ndipo
amene sakufuna Msiye).
13. (Malangizowa akuchokera)
Mmakalata olemekezedwa (Kwa
Mulungu);
14. Apamwamba ndiponso
oyeretsedwa (Kumbiri iliyonse
yopunguka);
15. Omwe ali m'manja mwa
Alembi (Angelo).
16. Olemekezeka, omvera.
17. Waonongedwa
(watembereredwa) Munthu.
Mkwanji kusayamika Kwake
kotereku.
18. Kuchokera mchinthu chanji
Chimene iye adamulenga.
19. Kuchokera kumadzi
(opanda pake) Adamulenga,
namkonzeratu mkalengedwe
Kosiyanasiyana.
20. Kenako adamfewetsera njira
(Yotulukira m'mimba mwa mai
ake).
21. Ndipo amamchititsa kuti
Amwalire namukumbila manda,
22. Kenako akadzafuna
adzamuukitsa (Pambuyo pa imfa).
23. Ayi ndithu (munthu)
sanakwaniritsebe Zimene
@tf
tfjOMiiy
c^ 3
I ^<3^i$
Surat 80, 'Abasa Juzu 30 1326 ? * *&
A * ,j~* 5 j>^
adamulamula Mbuye wake
(Mulungu chingakhale Wakhala
nthawi yaitali padziko Lapansi).
24. Alingalire munthu (mmene
chilili) Chakudya chake; 1
25. Ndithu, Ife timagwetsa
mvula Yambiri (kuchokera ku
mitambo).
26. Kenako timaing'amba
nthaka kuti Mmera utuluke;
27. Ndipo timameretsa
m'menemo njere (ya Chakudya
cha anthu ndi zina Zimene
amasunga kunkhokwe),
28. Ndi mphesa ndi msipu.
29. Ndi mzitona (wabwino) ndi
(Zipatso za) kanjedza,
30. Ndi minda yothothana
nthambi Za mitengo,
31. Ndi zipatso (zodyedwa ndi
anthu) Ndi msipu (wodyedwa ndi
nyama);
32. (Tazimeretsa zimenezo kuti)
Zikondweretse inu ndi ziweto
Zanu.
33. Ndipo likadzafika lipenga
Logonthetsa mkhutu (ndi kuumitsa
Makosi).
b\&?$&\i
^<&%'g%
&&±%ptiz
©<tLik)l^Cl3b
1 Ngati munthu sakumbuka chilengedwe chake, ayang'ane chakudya chimene
akudya momwe chimapezekera. Azindikira mphamvu za Mulungu.
Surat 80. 'Abasa
Juzu 30
1327
r* fijk-\
A * ^p-P 9jJ~>
34. Patsikuli munthu adzathawa
m'bale Wake,
35. Mayi wake ndi bambo wake,
36. Mkazi wake ndi ana ake.
37. Munthu aliyense mwa iwo,
tsiku Limenelo adzakhala ndi
zakezake Zotangwanika nazo.
(Sadzalabadira Za anzake).
38. Tsiku limenelo nkhope zina
Zidzakhala zowala; 1
39. Zosekelera ndi
zachimwemwe (Chifukwa cha
nkhani yabwino ya Kumunda wa
mtendere.)
40. Ndipo nkhope zina tsiku
limenelo Zidzakhala zokutidwa ndi
fumbi.
41. Mdima udzadzikuta.
42. Iwo ndi anthu
osakhulupirira Oipa (olakwira
Mulungu).
* A 9 • 9 .&
&&&L&
y(k'"t<'9f - '9&*9999'
1 (Ndime 38-39) Tsiku limenelo anthu adzakhala kakhalidwe ka mitundu iwiri:
amene adakhulupirira ndi kuchita ntchito zabwino nkhope zawo zidzawala
ndi chimwemwe, ndipo amene adakanira ndikumachita zoipa, nkhope zawo
zidzakhala zafumbi ndi zakuda monga momwe anenera ma aya 40 ndi 42.
Surat 81. At-Takwir Juzu 30
1328
r. *>»
A > jjj^sll 5 jj-»
SURAT AT-TAKWIR LXXXI
Surayi ikupereka chithunzithunzi chammene zinthu
zidzakhalira kumayambiriro kwa tsiku la Kiyama ndi pambuyo
pake. Ndipo yasonyeza maonekedwe amphamvu zake
ndikutsimikiza ulemerero wa Qur'an ndikumuyeretsa Mtumiki
ku misala imene amamganizira nayo. Ndipo yawaopseza
opitiriza kusokera, ndikunenetsa kuti mQur'an muli maphunziro
othandiza kwa anthu olungama.
Surat At-Takwir LXXXI
r
^J^^ ^^2^^_y^\
V&m$]
' .-re- i$cv?
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Pamene dzuwa
lidzakulungidwe (Ndikuchotsedwa
kuwalakwake), 1
2. Ndi pamene nyenyezi
zidzathothoke (Ndi kuchoka
dangalira Lake),
3. Ndi pamene mapiri
adzayendetsedwe (Kuchoka
mmalo mwake), 2
4. Ndi pamene ngamira zabere
Lamiyezi khumi zidzasiidwe
(Zopanda oziyanga'anira), 3
o^l^jll^U-
-^
m
%a&xj^m
1 Surah zambiri zimene zidavumbulutsidwa ku Makka zimanena zododometsa
za tsiku lomaliza. Kuyambira ayah iyi mpaka kudzafika ayah 14 Mulungu
watchula zina zododometsa za tsiku lomaliza.
2 Tsiku limenelo mapiri adzakhala osalimba ngati thonje limene likungouluka
ndi mphepo.
3 Ngamira za bere ndi chuma cha mtengo wapatali kwa Aarabu. Akuuzidwa
apa kuti tsiku limenelo adzazisiya osalabadira konse.
Surat 81. At-Takwir Juzu 30
1329
»>'
A> jlj&^\ *jj-»
5. Ndi pamene nyama za
mtchire Zidzasonkhanitsidwe
pamodzi (kuchokera mmalo
osiyanasiyana Chifiikwa
chakuopsa kwakukulu kwa
Tsikulo), 1
6. Ndi pamene nyanja
zidzayatsidwe Moto,
7. Ndi pamene mizimu
idzalumikizidwe (Ndi matupi ake) ?
8. Ndi pamene mwana wamkazi
yemwe Adaikidwa m'manda
wamoyo Adzafunsidwe, 2
9. Ndi tchimo lanji adaphedwera?
10. Ndi pamene makalata
(mom we Mudalembedwa zochita
za aliyense) Adzatambasulidwe
ndi kugawidwa (Kuti
awerengedwe), 3
11. Ndi pamene thambo
lidzayalulidwe (Kuchoka mmalo
mwake),
$&y£(j*£y\\&5
©(s^CA9*a!lbb
af<£&r&i!llSi;
mtchire
Mwa zina zododometsa pa tsiku limenelo ndi nyama za
kusonkhanitsidwa pamodzi popanda kumenyana kapena kudyana.
2 (Ndime 8-9) Ma ayah awiriwa akufotokoza momwe Aarabu adaiili Usilamu
usadabwere. Munthu ankati akapatsidwa mphatso ya mwana wa mkazi adali
kukhumudwa ndi kudandaula kwambiri. Ankanena kuti asungwana ngopanda
phindu ndipo kuti kudali kuononga zinthu pakumulera , kumudyetsa, ndi
kumuveka. Ndipo akadzakhala wachiwerewere adzakhala manyazi aakulu
kwa makolo ake. Pamene chidadza chisilamu chidathetsa mkhalidwewu.
Ndipo apa Mulungu akutisonyeza kuti patsiku limenelo, la chiweruzo, mwana
uja adaikidwa wa moyo, adzafunsidwa kuti adaphedwa ndi tchimo lanji. lye
adzayankha kuti sadachite tchimo lililonse koma adaphedwa mopanda
chilungamo.
3 Awa ndi makalata achiwerengero momwe mwalembedwa zabwino za
munthu ndi zoipa zake. Tsiku limenelo munthu aliyense adzapatsidwa yake
kalata kuti aone iye mwini zoipa ndi zabwino zake.
Surat 81. At-Takwir Juzu 30
1330
*>'
A 1 jt£d\ 5j>-»
12. Ndi pamene Jahena
idzasonkhezeredwe
Mwamphamvu, 1
13. Ndi pamene Jannah
idzayandikitsidwe,
14. (Zikadzachitika zimenezi)
mzimu Uliwonse udzadziwa
zimene Wabweretsa (zabwino ndi
zoipa).
15. Ndikulumbirira nyenyezi
zimene Zimabwerera masana ndi
kutulukanso Usiku.
16. Zomwe zimayenda kenako
nkubisika,
17. Ndi usiku pamene ukulowa.
18. Ndi m'mawa kukamacha;
19. Ndithu iyi (Qur'an) ndi liwu
la mthenga Wa Mulungu (Jibril)
wolemekezeka (kwa lye),
20. Mwini mphamvu ndi mwini
ulemelero Kwa Mwini Mpando wa
chifumu,
21. Womveredwa kumeneko
ndiponso Wokhulupirika
(pachi vumbulutso) .
1 (Ndime12-13) Tsiku limenelo Jannah idzayandikitsidwa kwa ochita zabwino
ndiponso moto udzayandikitsidwa kwa ochita zoipa kuti aone kumalo kwake.
2 (Ndime 19-20) Mthenga wolemekezeka womveredwa uko kumwamba ndi
Jibril (Gabriel) yemwe ndi wamkulu wa angelo onse. lye ndiyemwe adali
kubweretsa Qur'an mwa lamulo la Mulungu kwa Mneneri Wake Muhammad
(SAW). Ndipo ulemelero wa Qur'an ndi ulemelero wa Mneneri (SAW)
chifukwa choti munthu wolemekezeka amamutumizira mthenga
wolemekezeka. Ndipo uthenga wabwino umapatsidwa kwa Mneneri wabwino
woposa onse.
Surat 81. At-Takwir Juzu 30
1331
f » f,j)r\ A ) jij^sll ijj*t
22. Ndipo m'bale wanu uyu
siwamisalaayi. 1
23. Ndithu, ndikulumbira kuti
(iye Mtumiki) (SAW) Adamuona
(Jibril) mchizimezime
(chakum'mawa) Chooneka bwino.
24. Ndipo sali iye (Mtumiki)
waumbombo Ndi chivumbulutso
(koma amafikitsa zonse
Ndikuziphunzitsa kwa anthu).
25. (Chivumbulutso chomwe
chavumbulutsidwachi Kwa iye) si
mawu a satana wothamangitsidwa
Mchifundo cha Mulungu;
26. Nanga mukupita kuti?
27. (Qur'ani) iyi sichina koma
Ndi chikumbutso cha Zolengedwa
zonse.
28. Kwa yemwe mwa inu
akufuna Kuyenda mu njira
yoongoka.
29. Ndipo simungafune chinthu
mwa Inu nokha pokhapokha
atafuna Mulungu Mbuye wa
zolengedwa zonse.
1 (Ndime 22-25) Anthu okanlra pamene adasowa chonena kwa mneneri
(SAW) adali kunena nkhani zabodza kuti Mtumiki (SAW) wapenga ndikuti
zomwe akulankhula sadapatsidwe ndi Jibril,
Surat 82. Al-Infitar Juzu 30
1332
**\
AT jlkiW 5j>-»
Surayi yasonyeza zina mwazoopsa zimene zidzachitike tsiku
la Kiyama ndi malankhulidwe osonyeza kuti zichitikadi
posachedwa, patsiku limene munthu aliyense adzadziwa zimene
adatsogoza ndi zomwe adazisiya. Kenako surayi yachenjeza
munthu wonyengedwa pakusalabadira Mulungu wake amene
adamlenga ndikumlinganiza bwino. Ndipo adampatsa
maonekedwe abwino, olingana. Ndipo kenako yatsimikiza
kukanira kwa munthu za tsiku la chiweruzo, ndikutsimikiza kuti
munthu ali nawo angelo omwe akulemba chilichonse. Ndipo
yatsatiza pankhaniyi kutchula za mtendere womwe anthu
abwino adzapeza, ndiponso Jahena imene idzakhala ya anthu
oipa; adzailowa pa tsiku la Kiyama lomwe ndi tsiku limene
mzimu sudzakhala ndi mphamvu zothangatira mzimu wina.
Ndipo zonse zidzakhala za Mulungu yekha.
Surat Al-Infitar LXXXII
I mm%
■ ;?"}-
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Pamene thambo lidzasweke, 1
2. Ndi pamene nyenyezi
zidzayoyoke (Ndi kumwazikana),
3. Pamenenso nyanja
zikuluzikulu Zidzaphwasulidwe.
4. Ndiponso pamene manda
Adzafukulidwe (ndikutuluka
Akufa omwe adali mmenemo),
o^i^JMkU.
1 Kuyambira pa aya 1 mpaka 4, Mulungu akutisonyeza zododometsa zina za
tsiku lomaliza.
Surat 82. Al-Infitar Juzu 30 1333 r * *>»
AT jlW}|1 5jj^»
5. (Panthawiyo) mzimu
uliwonse Udzadziwa zimene
Udatsogoza (zabwino ndi zoipa)
Ndi zimene udasiya m'mbuyo. 1
6. E! Iwe munthu! Nchiani
chakunyenga Kumsiya Mbuye wako
wa ufulu (Kufikira pomnyoza)?
7. Amene adalenga iwe
Nakulinganiza (ziwalo zako) ndi
Kukulongosola (moyenera);
8. Ndipo maonekedwe amtundu
Uliwonse omwe adawafuna
Adakuveka (popanda chifuniro
Chako).
9. Ayi, sichoncho! Koma inu
Mukutsutsa za (tsiku) lamalipiro.
10. Ndithu, pa inu alipo
okuyang' anirani, 2
11. Olemekezeka, olemba
(zochita Zanu.)
12. Akudziwa (zonse) zimene
muchita (Zabwino ndi zoipa).
13. Ndithudi ochita zabwino
Adzakhala mumtendere.
14. Ndipo ndithu, amene ali
olakwira Malamulo a Mulungu
adzakhala Ku moto wopsereza.
15. Adzaulowa tsiku la malipiro.
©(j^JJI
^r^'ft?
1 Munthu aliyense pa tsiku limenelo adzadziwa zimene adachita, zabwino ndi
zoipa.
2 Munthu aliyense ali nawo angelo awiri, Rakibu ndi /
kulemba ntchito za munthu, zabwino ndi zoipa zomwe.
zoipa.
2 Munthu aliyense ali nawo angelo awiri, Rakibu ndi Atidu. Ntchito zawo ndi
Surat 82. Al-Infitar Juzu 30 I 1334 T * *>i At jiWsM «j>-
16. Ndipo iwo kumoto
Sadzachokako.
17. Kodi nchiyani
chingakudziwitse za Tsiku la
malipiro?
18. Ndipo nchiyani
chingakudziwitse za Tsiku la
malipiro?
19. Limeneli ndi tsiku limene
mzimu Uliwonse sudzakhala ndi
mphamvu (Yodzetsa mtendere
kapena Yochotsa chovuta) pa
mzimu wina. Ndipo lamulo pa tsiku
limeneli Ndi la Mulungu yekha. 1
Surayi yayamba ndikulonjeza za chilango choopsa kwa
amene akuphangira pamalonda; popatsa ena zosakwanira
pamuyezo wake. Ndipo anthu amtundu uwu yawaopseza kuti
adzauka mmanda ndikuwawerengera zochita zawo, ndipo
yanenetsanso kuti ntchito zawo zikulembedwa mkaundula
wowerengedwa malembo bwinobwino.
Tsiku limenelo palibe angalikanire kupatula wopyola malire
ndi wamachimo ambiri. Wotereyo sakamuona Mbuye wake.
Ndipo kobwerera kwake ndi ku Jahena.
Surayi yatchulanso za anthu abwino ndikuwatonthoza
ndikuwapatsa chikhulupiriro cha kupambana pantchito zawo
zabwino. Ndipo yafotokozanso zamtendere wawo ndikupambana
Tanthauzo lake ndikuti tsiku limenelo sipadzakhala munthu wotha
kumthandiza mnzake pa chilichonse ndiponso palibe adzakhale ndi mphamvu
zolamula kupatula Mulungu yekha.
Surat 83. Al-Mutaffifin Juzu 30 1335 T ♦ ^j*-i AT osiibli h**>
kwawo. Kenako surayi yatipatsa chithunzithunzi chamomwe
Akafiri ankawachitira Asilamu pamene ankaona Asilamu
akuwadutsa. Surayi yamaliza ndikulongosola kuti naonso
Asilamu adzabwezera chipongwe kwa Akafiri pa zomwe
ankawachitira padziko lapansi.
Surat At-Mutaffijln LXXIII
r^^ 1
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Kuonongeka koopsa
kukawapeza Opunguza miyezo ya
malonda
2. Amene amati Akamadziyezera
zinthu kwa anthu amafuna
Kulandira miyezo yodzadza.
3. Koma pamene iwo
akamawayezera pa Muyezo
wambale kapena wa sikelo
Amapungula (choyenera kulandira
Ogulawo).
4. Kodi amene akupungula
miyezo Pamalondawo sakuganiza
kuti Adzaukitsidwa;
5. Pa tsiku lalikulu (ndiponso
Loopsa)?
6. Tsiku limene adzaimilira anthu
Pamaso pa Mbuye wa zolengedwa.
7. Ayi! Ndithu (siyani chinyengo
Pamalonda ndi kusalabadira kuuka
Mmanda); Zolembedwa za ntchito
Ya oipa zili m'Sijjin.
Q
>^l<^5MkU-
( %feWcS
$&&jw#mw$
x '^^^jtef'iVfJi&if
j&&j&&®x
Surat 83. Al-Mutaffifin Juzu 30
1336
r» *>i
AT ooilail Ojj-rf
8. Nanga nchiyani
chitakudziwitse Za Sijjin?
9. Ameneyu ndi kaundula
Wamkulu yemwe walembedwa
(Mkati mwake ntchito za Anthu
oipa).
10. Chilango chaukali tsiku
Limenelo chili pa otsutsa, 1
11. Amene akutsutsa Za tsiku la
malipiro.
12. Ndipo palibe angalitsutse
Koma yekhayo wopyola malire
(Pochita zoipa); wa machimo
Ambiri;
13. Pamene ma ayah Athu
akuwerengedwa kwa iye (onena za
tsiku La malipiro ndikuuka
mmanda) Amanena kuti "Izi ndi
nthano Za anthu akale."
14. Iyayi ? sichoncho! Koma
Yaphimbidwa mitima yawo ndi
Dzimbiri (la machimo) omwe
Akhala akukolola. 2
0<J^\i<^jSllj
*J9>l?%9l K
$®'f$&Q?($$
s>9 >6
1 Kutsutsa kulipo kwa mitundu itatu:
(a) Kutsutsa kwa mawu ndi zochita;
(b) Kutsutsa kwa zochita zokha, monga ukauzidwa kuti chinthu ichi nchoipa,
munthu nkudziwa kuti zoona nchoipadi koma nkudzachichita chimenecho
mosalabadira;
(c) Kutsutsa ndi zolankhula zokha. Kumeneko ndiko monga munthu akudziwa
kuti chakutichakuti ncholetsedwa (haramu) koma m'malo mwake iye nkumati
chimenecho nchovomerezeka (halali)
2 Munthu akachita choipa koyamba ndipo osalapa, limalowa dontho lakuda
mu mtima mwake; nthawi iliyonse pamene akuonjezera machimo, dontho lija
limakulirakulira mpaka kuuphimba mtima wonse. Dontho limeneli ndilo
likutchedwa "Ran." Tsono mtima ngati utaphimbidwa chotere sulabadira
kuchita zoipa, ngakhale kuti auongole sungaongoke.
Surat 83. Al-Mutaffifin Juzu 30 1337 T • >>» AT &M\ oj^
15. Ayi ndithu iwo (okanira)
tsiku Limenelo) adzatchingidwa
Kwa Mbuye wawo; (Sadzamuona).
16. Pambuyo pake adzalowa ku
Moto; (oyaka)
17. Kenaka adzauzidwa
(Powaliritsa) "Ichi Ndi chilango
chomwe Mudali kuchitsutsa (pa
dziko Lapansi)."
18. Zoona, ndithu, kaundula wa
Anthu abwino (ochita ntchito
Zabwino) ali mu Illiyyun.
19. Nanga nchiyani
chitakudziwitse za Illiyyun?
20. Ameneyu ndi kaundula
(wamkulu) Yemwe walembedwa
(mkati mwake Ntchito za anthu
abwino);
21. Amamuyikira umboni
(angelo) Amene ayandikitsidwa
(kwa Mulungu).
22. Ndithu, ochita zabwino
Adzakhala mu mtendere,
23. Atakhala pa mipando ya
ulemu Uku akuyang'ana (zimene
Mulungu wawapatsa monga
Mtendere ndi ulemerero).
24. Udzaona kuwala kwa
mtendere Pa nkhope zawo;
25. Adzamwetsedwa vinyo
(woyeretsedwa) Wotsekeredwa ndi
zitsekero Zolimba;
b '29*9 9'
Surat 83. Al-Mutaffifin Juzu 30 1338 r * *>»
AT ONtfkit 5jj--
26. Komalizira kwake (kwa
vinyoyo) Kuzikatuluka fungo la
misk; Kuti akapeze zimenezi,
apikisane Opikisana. 1
27. Ndipo chosakanizira cha
Vinyoyo ndi madzi a Tasnim.
28. (Tasnim ameneyo) ndi
kasupe Amene azikamwa amene
ayandikitsidwa (Kwa Mulungu.)
29. Ndithu, amene adachita
machimo Adali kuwaseka
(mwachipongwe) Okhulupirira
(padziko lapansi);
30. (Okhulupirira) Akadutsa
pafupi ndi iwo Ankakodolerana
maso (Mwachipongwe);
31. Ndipo akabwerera kwa
anzawo Amabwerera akusangalala
(Ndi kunyozedwa kwa
okhulupirira);
32. Ndipo (nthawi zonse)
akawaona Asilamu amanena:
"Ndithu, awa Ndi osokera
(chifukwa chomkhulupirira
Mtumiki)." (SAW)
33. Sanatumizidwe (Akafiri)
kukhala Ayang'aniri kwa
okhulupirira (Ndikuwaweruza
zakulungama ndi Kusokera).
1 Apa, akutilamula kupikisana pakuchita zabwino kuti tipeze madalitso amene
awakonzera anthu abwino. Kumeneko ndikuti munthu aliyense alimbikire
kuchita mapemphero ndi zina zabwino.
(J&&£$X&&Z*®r
©(j ^ «»jl:J J\
®<<M^
0(1$ wJ
e ®&^4Jfc
Surat 83. Al-Mutaffifin Juzu 30
1339
*>'
fs? j^ilail 5jj-*»
34. Basi patsikulo okhulupirira
adzaseka Osakhulupirira
(powabwezera chipongwe Chawo
chimene ankachita padziko
Lapansi), 1
35. Atakhala pa mipando ya
ulemu uku Akuyang'ana
(mtendere umene Mulungu
Wawapatsa).
36. Kodi alipidwa
osakhulupirira Pazomwe ankachita
zija (padziko Lapansi)?
iS&i«5*ijft&A3&
l" "
®£n4®&-
© (j^l^ly^^j^lo^^
Surayi yalongosola zina mwazisonyezo za Kiyama ndikuti
nthaka ndi thambo zidzagonjera zofuna za Mulungu. Ndikutinso
munthu adzakumana ndi Mbuye wake Mulungu. Ndikutinso
zochita zake zikulembedwa m'buku limene adzaliona
ndikulilandira. Amene adzalirandire ndi dzanja lamanja, ndiye
kuti chiwerengero chake chidzakhala chofewa, pomwe amene
adzalirandire ndi dzanja la kumanzere ndiye kuti adzalira
kwambiri kuopa kukumana ndi chilango chamoto.
Kenako Mulungu walumbirira zoonekera mwazisonyezo
Zake zomwe zikuikira umboni mphamvu Yake,ndikuitanira ku
chikhulupiriro cha kuuka kwa akufa. Koma ngakhale zili
chonchi, anthu okanira sakhulupirira ndi kulingalira Qur'an
ndikugonjera malamulo ake.
Surayi yamaliza ndi kuopseza kuti Mulungu akudziwa
1 (Ndime 34-36) Tanthauzo lake ndikuti okhulupirira, tsiku lomaliza adzakhala
m'mipando ya ulemu uku akuwayang'ana ndi kuwaseka anthu osakhulupirira
ali m'mavuto monga momwe iwo adali kuseka okhulupirira pa dziko lapansi.
Surat 84. Al-Inshiqaq Juzu 30 1340 I T • *>» At JlLSJ* 5jj-
zimene akubisa mmitima mwawo. Ndipo wawakonzera chilango
chowawa. Chimodzimodzinso kwa okhulupirira, wawakonzera
mphoto yokoma yamuyaya.
Surat Al-Inshiqaq LXXXIV
w%tf:
\mm&^ym
OJj*&\uP&\fr\j>.
-&
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Pamene thambo
lidzang'ambike (Kusonyeza
mapeto ake),
2. Ndikudzamvera lamulo la
Mbuye Wake; ndipo lidzayenera
kutero,
3. Ndiponso pamene nthaka
Idzatambasulidwe (pogumuka
Mapiri ake ndikuchoka zitunda
zake),
4. Ndi kutaya zomwe zidali
mkati Mwake ndi kukhala
Yopandakanthu, 1
5. Ndikudzamvera lamulo la
Mbuye Wake; ndipo lidzayenera
kutero. (Choncho Zikadzachitika
zimenezi ndiye kuti munthu
Adzalandira mphoto ya zochita
zake). 2
1 Chimodzi mwa zinthu zoopsa zomwe zidzachitika tsiku lomaliza ndi
kugwedezeka kwa nthaka mwamphamvu zedi mpaka idzalekana ndi mapiri
amene ali zichiri zake zoletsa kugwedezeka kwake. Pachifukwa ichi
idzatambasuka ndipo zomwe zidali mkati mwake zidzatulukira pamtunda;
nthaka idzangokhala yopanda kanthu mkati mwake.
2 Ambuye Mulungu pambuyo ponena zimenezi sadanene kuti chidzachitika
&£B\jfc3\\k
©<c*£>^ \& y J, <c* $j
Surat 84. Al-Inshiqaq Juzu 30 1341 r • *>■! At JUL^i Sj^
6. E! I we Munthu! Ndithudi iwe
Ukubwerera kwa Mbuye wako
(ndi Zochita zako zabwino kapena
Zoipa), kubwerera kotsimikizika,
Ndipo iwe ukumana (ndi zotsatira
Za zochitachita zako).
7. Tsono amene adzapatsidwe
kaundula Wa zochita zake
kudzanja La manja, 1
8. Basi iye, adzawerengedwa,
Kuwerengedwa kopepuka, 2
9. Ndipo adzabwerera kwa anthu
ake (Okhulupirira) ali wokondwa.
10. Koma yemwe adzapatsidwe
kaundula Wa zochita zake
chakumanzere Kudzera kumbuyo
kwa msana wake (Chifukwa
chomunyoza),
11. Basi, iye adzaitana imfa
(kuti Imufikire; kuti afe apumule,
Koma siidzamufikira);
12. Ndipo adzalowa ku moto
woyaka.
i^JC^&W
®\%?«<^*l$
chiyani. Alekera munthu mwini wake kuti aganizire chomwe chidzachltika
zikadzapezeka zoopsa kuti aope kwambiri.
1 Tsiku la chiweruzo munthu adzapatsidwa kaundula wake monga momwe
zanenedwa mu ayah 10 Surah Takwir, choncho ena adzapatsidwa ndi dzanja
la kumanja; iwo ndiwo anthu abwino. Pomwe ena adzapatsidwa ndi dzanja la
kumanzere, chakumbali yakumsana; iwowo ndiwo anthu oipa.
2 Anthu ena adzawerengedwa popanda kufunsidwa mafunso pa zimene
adachita, koma adzangowauza zabwino zawo ndi zoipa zawo ndipo pambuyo
pake adzawakhululukira zoipazo ndi kudzawalipira pa zabwinozo. Iwowa ndiwo
anthu abwino; chimenechi ndicho chiweruzo chofewa. Ena adzaweruzidwa
pofunsidwa pa chilichonse m'zimene ankachita monga kuti "Bwanji ichi
udachita? Bwanji ichi sudachite"? Iwowa ndiwo anthu oipa; chiwerengero
chawo chidzakhala chokhwima.
Surat 84. Al-Inshiqaq Juzu 30 1342 T * *>» At JU^j^i Sj>-
13. Kamba kakuti iye adali
wokondwa; (Kukondwa kwa
machimo) pamodzi Ndi anthu ake
(osaganizira za Mathero ake).
14. Ndithudi,amaganiza kuti
Sadzabwerera (kwa Mulungu
ndiponso Sadzawerengedwa).
15. Chifukwa ninji
(asabwerere)? Mbuye wake adali
kumuona. (Choncho alipidwa
zimene adachita).
16. Ndikulumbirira kufiira Kwa
dzuwa (pamene likulowa).
17. Ndi usiku ndi zimene
wasonkhanitsa, 1
18. Ndi mwezi ukakwanira
dangalira (Lake),
19. Ndithudi mudzachoka apa
kunka apa (Pa umoyo uno
mpakana Umene uli nkudza).
20. Kodi nchiyani chikuwaletsa
iwo (Okanira) kukhulupirira
(Mulungu Ndi kuuka kumanda,
zisonyezo zake Zitaonekera
poyera)?
21. Ndipo ikawerengedwa kwa
iwo Qur'an, Sagwetsa pansi
nkhope zawo (Modzichepetsa).
®,
s ^mo$^&&
1 Kubalalikana masana ndi chizolowezi cha anthu ndi nyama chifukwa
chofunafuna zinthu zothandiza pa moyo wawo. Tsono usiku ukabwera
amasonkhana ndi kukhala pamodzi. Ndipo ili ndilo tanthauzo la "usiku ndi
zimene wasonkhanitsa."
Surat 84. Al-Inshiqaq Juzu 30 1343 r • *>» At JUjysh oj^-
22. Koma amene
sadakhulupirire Akutsutsa basi
(chifukwa cha Makani ndi
kudzikweza).
23. Ndipo Mulungu akudziwa
(bwinobwino) Zimene
akuzisonkhanitsa.
24. Choncho, auze nkhani
Yachilango chopweteka.
25. Kupatula awo amene
Akhulupirira ndikuchita Ntchito
zabwino, kwa iwo Kuli malipiro
osatha. 1
®*m&&M
,r .' '
Z. 9 9s'99'^>'\99\
SURAT BURU J LXXXV
M'surayi muli mawu omutonthoza Mtumiki ndikuwakumbutsa
Asilamu, ndiponso kuopseza ndi chilango kwa osakhulupirira.
Yayamba ndikulumbirira kwa Mulungu pa zisonyezo zosonyeza
mphamvu yake ndi luso lake lakuya pa chilichonse potsimikiza
kuti amene akuzunza okhulupirira adzathamangitsidwa kubwalo
la chifundo Chake, monga momwe adathamangitsidwira ochita
zoterezi mwa anthu akale. Ndipo surayi yalongosola za anthu
oipa ndi zimene adali kuwachitira okhulupirira. Yalongosolanso
kuti nthawi zonse choona chimathiridwa nkhondo ndi anthu
oipa. Ndipo yamalizira kunena kuti Qur'an ndi mawu oona;
mulibe chikaiko mkati mwake. Chifukwa idachokera m'buku
lotchedwa "Lauhi Mahfudhi" lomwe lili kwa Mulungu.
1 Ayah iyi ikusonyeza kuti kukhulupirira kokha sikungampulumutse munthu ku
chilango cha tsiku lomaliza, koma nkofunikanso kuchita ntchito zabwino;
m'Qur'an paliponse pamene akutchula za chikhulupiriro akutchulanso za
kuchita ntchito zabwino.
SOrat 85. Al-Buruj Juzu 30 1344
►J*"'
A© KJJ^\ ^j-j
Surat Al-Buruj LXXXV
' i$&£ ;*-
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Ndikulumbirira thambo
lomwe liri ndi Buruj (Nyenyezi
zikuluzikulu). 1
2. Ndi tsiku lolonjezedwa
(Kuwerengedwa ndi kulipidwa),
3. Ndi woikira umboni, ndi
woikiridwa umboni. 2
4. Atembereredwa eni ngalande
(mayenje) zamoto (Zomwe adali
kuwazunzira okhulupirira
Mulungu, Achimuna ndi
achikazi). 3
5. (Ngalande) za moto
wankhuni (zambiri zomwe Adali
o^t^^U.
-^
**#LylS<AM
1 Buruj ndi nyenyezi zomwe zimakhala m'magulumagulu ndipo gulu lililonse
limatchedwa Buruj. Ndipo Buruj zonse zilipo khumi ndi ziwiri (12). Zisanu ndi
imodzi zili kumpoto kwa "Equator", pomwe zisanu ndi imodzi zili kumwera kwake.
2 "Woikira umboni ndi woikiridwa umboni" angathe kukhala aliyense woikira
umboni ndi woikiridwa umboni pa tsiku lomaliza, monga aneneri adzaikira
umboni anthu pa zabwino kapena zoipa; pa malo pochitira mapemphero
padzamuikira umboni wazabwino yemwe adali kupempherapo. Ndipo pamalo
pomwe padali kuchitikira zoipa padzawachitira umboni anthu oipa za
machimo awo: ngakhale ziwalo ndi khungu nazonso pa tsiku limenelo
zidzaikira umboni kwa mwini ziwalozo. Basi munthu akatsimikiza kuchita
machimo akumbukire kuti ali nazo mboni zambiri zomwe zikumuona ndipo pa
tsiku la chiweruzo zidzaima pa maso pa Mulungu kupereka umboni wokhudza
munthuyo.
3 Pamene Ayuda a ku Najrani adalowa m'Chikhristu, (Chisilamu chisadafike
ndiponso Chikhristu chisadaonongeke), idamufika nkhaniyi mfumu yawo dzina
lake Dhu-Nuwas; adabwera ku Najrani ndi gulu lankhondo lalikulu;
adawakakamizira anthu ku Chiyuda koma iwo adakana. Nayamba kuwapha
anthu okhulupirirawo powaponya m'ngalande za moto.
Surat 85. Al-Buruj Juzu 30 1345 T * tjk-\
Ad j- jjt\ oj^
kuzikoleza ndikuotchera
okhulupirira),
6. Pamene iwo adali chikhalire
m'mphepete mwa Ngalande za
moto.
7. Uku iwo akuyang'ana zomwe
amawachitira Okhulupirira,
(pootchedwa ndi moto).
8. Sadaone choipa chilichonse
mwa iwo koma Chifukwa choti
adakhulupirira Mulungu mwini
Mphamvu zonse ndiponso mwini
kuyamikidwa,
9. Yemwe ufumu
wakumwamba ndi pansi ndi Wake;
ndipo Mulungu ndi mboni
pachilichonse.
10. Ndithu, amene ayesa
mayeso okhulupirira achimuna Ndi
achikazi (pa chipembedzo chawo
ndi Mazunzo ndi chilango cha
moto), pambuyo pake Osalapa
(pazimenezi), adzalandira chilango
cha Jahena Ndiponso chilango cha
moto wopsereza, 1
11. Ndithudi amene
akhulupirira ndi kuchita ntchito
Zabwino, adzakhala ndi minda,
(mom we) mitsinje Ikuyenda pansi
&>j&&&>\
1 Tanthauzo la "kuwazunza" apa ndiko kuwavutitsa ndi kuwathetsa mphamvu
kuti asiye chikhulupiriro chawo; asakhulupirire mwa Mulungu. Mawuwa
ngakhale akukhudzana ndi eni mayenje a moto, akukhudzanso akafiri a
m'Makka omwe adali kuzunza Asilamu ndi mazunzo osiyanasiyana kuti
abwerere kuchipembedzo cha mafano. Ndipo zimenezi zikhudzanso aliyense
Surat 85. AI-Buriij Juzu 30
1346
r% *j*-i
Ao r jjJl *JJ~*'
pake; kumeneko ndiko
Kupambana kwakukulu.
12. Ndithu, kulanga kwa Mbuye
wako (kwa Anthu achinyengo), ndi
kwaukali kwambiri . l
13. lye, (mmodzi yekha) ndi
amene Adayambitsa zolengedwa
ndiponso Ndi yemwe adzazibweze
(pambuyo Poonongeka);
14. lye, ndi Wokhululuka (kwa
amene Walapa kwa lye), ndiponso
Wokonda Kwambiri (amene
akumkonda ndi Kumumvera),
15. Mwini mpando wachifumu,
(ndiponso) Wolemekezeka
(mmene alili ndi Mbiri Zake),
16. Wochita zimene wafuna,
(ndipo Chimene wafuna
sichikanika).
17. Kodi yakufika nkhani ya
magulu a nkhondo,
©L)J^^jJ^(ji
1 (Ndime 12-16) Ambuye Mulungu pambuyo powatonthoza Asilamu
pakuwauza zomwe zidawaonekera abale awo amene adatsogola, tsopanonso
akuwatonthoza ndi ufumu Wake wolemekezeka kuti adziwe kuti awo akafiri
omwe akudziona kuti ali ndi mphamvu zolangira anzawo, lye sangamuthe.
Akafuna adzawalanga ndi chilango cha dziko lapansi ndi cha tsiku lomaliza,
kapena chimodzi mwa zilangozi; pakuti lye Ngokhululuka kwambiri ndiponso
Ngwachikondi zedi, awatembenula mitima yawo kuti achikhulupirire chimene
adachikana. Chifukwa cha mphamvu Zake zoposa, Mulungu, adachita
zonsezi ziwiri. Patapita zaka zochepa adawapatsa mphamvu omwe adali
opanda mphamvu, kenaka adayamba kuwalanga osakhulupirira aja chilango
cha padziko, monga Abu Jahl ndi anzake omwe adali kumutsutsa kwambiri
Mtumiki (SAW) pamodzi ndi omutsatira ake. Ndipo ena adawatembenula
mitima yawo nkulowa mchipembedzo cha Chisilamu; adaima ndikuchiteteza
Chisilamu popereka nsembe ya mizimu yawo ndi chuma chawo.
Surat 85. Al-Buruj Juzu 30 1347 T * *>i
A 6 £Jj$\ *JJ~*
18. Firiaun (Farao) ndi Samudu,
(Ndi chilango chimene
chidawapeza Chifukwa
chakulimbikira kwawo pa Zinthu
zopanda pake)?
19. Koma amene
sadakhulupirire ali Mkati motsutsa
basi.
20. Koma Mulungu awazinga
mbali Zonse.
21. Koma iyi ndi Qur'an
yolemekezeka.
22. Yomwe idachokera mu
ubawo (Chisileti chachikulu)
wotetezedwa (Ndi manja alionse,
osintha kanthu Kapena
kuonjezerapo).
h S9f' ' S9'9.
>j+>) vjP-j}
®^My&&#\&
m&$&M
a;;: ■ .
SURAT AT-TARIQ LXXXVI I'j^^ff
Js^fe"! 1 k „;_ „^-~- ^P^Jll&
Surayi yayamba ndi kulumbirira nyenyezi zowala kwambiri
zomwe zikusonyeza mphamvu ya Mulungu pachilichonse.
Ndipo surayi ikutitsimikizira kuti aliyense alinaye msungi
wake.Ndiponso ikumulangiza munthu kuti aganizire za kubadwa
ndi kukula kwake, ndikuti adziwe kuti adalengedwa kuchokera
kumadzi ofwamphuka kuti potero apeze zizindikiro zoti amene
adamlenga kuchokera ku madzi,sangalephere kumuukitsa
kuchokera mmanda.
Ikulumbiriranso kuti Qur'an ndi mawu olekanitsa pakati pa
choona ndi chonama. Koma akafiri akuikanira ndikuitchera
misampha ngakhale ili choncho. Nayenso Mulungu wabwezera
misampha yakuti ikawagwetse ku chionongeko chomwe
Surat 86. At-Tariq Juzu 30 1348 T * *>»
An JjUail djj**
chidzakhala malipiro a kukanira ndi makani awo. Ndipo surai
ikumuwuzanso Mneneri (SAW) kuti awalekerere Akafiri mpaka
pomwe Mulungu adzaona chochita nawo.
Surat At-Tariq LXXXVI
,'iV*^ T ,'V'V
= "r^ =
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Ndikulumbirira ku mwamba
ndi Nyenyezi imene imadza usiku,
2. Chitakudziwitse nchiyani za
Nyenyezi yodza usikuyo?
3. Imeneyo ndi nyenyezi
yowala kwambiri (mu mdima).
4. Ndithudi palibe mzimu
uliwonse koma uli ndi msungi
Wake (amene akuuyang'anira
Ndikulemba zonse zochita zake).
5. Aganizire munthu, kodi
adalengedwa Kuchokera
kuchiyani?
6. Adalengedwa kuchokera ku
Madzi ofwamphuka.
7. Amatuluka kuchokera pakati
pa Mafupa a msana ndi chifuwa (A
munthu wa mwamuna ndi mkazi).
8. Ndithujye ndiwakutha,
Kum'bwezeranso (ku moyo
pambuyo paimfa).
9. Tsiku limene zobisika zonse
Zidzaonekera poyera.
Wtz mm&T<m
o£g\<£&\A\j
-^
6&mXi2\i
©&j^<*Ly;i%
^^\&&m
&fik&&$
&&&&?£
Surat 86. At-Tariq Juzu 30 1349 T * ^jJfe-i A\ JjlWi 5^
10. Munthu sadzakhala ndi
mphamvu (Tsiku limenelo
zodzitetezera lye mwini) ndiponso
sadzakhala Ndi mtetezi.
11. Ndikulumbiriranso mitambo
yobweretsabweretsa mvula.
12. Ndi nthaka imene
imang'ambika (Potulutsa m'mera),
13. Ndithudi iyi (Qur'an) ndi
mawu Olekanitsa (Haq ndi Batwili
- Choona ndi chonama).
14. Imeneyi sinkhambakamwa.
15. Ndithudi iwo akukonza
Chiwembu. 1
16. Nanenso ndikuwakonzera
Chiwembu (champhamvu
kwambiri Chimene sangathe
kuchipewa).
17. Basi, apatse nthawi
Osakhulupirira apatse Nthawi
pang'ono, (aona posachedwa).
&v$to&&*m
©l^I^j
©I^J^^t(^^(^6p
1 (Ndime15-16) Tanthauzo lake ndikuti akafiri (osakhulupirira) akuchita ndale
kuti azimitse dangalira la Qur'an ndikuyesetsa kuti awabweze amene
adakhulupirira ndiponso ndikufuna kumupha Mneneri (SAW). Naye Mulungu
akuwach'itira ndale powaonongera ziwembu zawo zomwe amaz'ikonza.
Surat 87. Al-A'la Juzu 30 1350 T • >>»
AV JIp^I 5j>-
SURAT AL-A'LA LXXXVII
wmm§
Surayi yayamba ndikulemekeza Mulungu amene adalenga
zinthu ndikuzichita kukhala zofanana mkalengedwe. Ndipo
chilichonse adachipatsa zoyenera zake ndikuchiongolera
kuzimenezo. Adameretsa mmera, ndipo kenako nkuuchita
kukhala wouma ndi wodera.
Kenako surayi yanena kuti ndithu, Mulungu
amamuwerengera Qur'an Mneneri Wake. Ndipo aloweza mu
mtima mwake chowerengacho; saiwala chilichonse kupatula
chimene wafuna lye mwini Mulungu. Ndipo amufewetsera
kuchita zinthu zabwino.
Kenakanso surayi ikulamula Mtumiki kuti awakumbutse
amene akuopa Mulungu powalalikira Qur'an kuti akumbukire
ndi kuthandizidwa ndi ulalikiwo. Koma woipa, mwini mavuto,
adzipatula ku ulalikiwo. Ndipo akalowa ku moto waukulu.
Surayi yatsimikiza kuti kupambana kuli kwa yemwe
wayeretsa mtima wake ndikumakumbukira dzina la Mulungu
uku akupemphera. Ndipo yamaliza ndikulongosola zimene
zidalembedwa mmabuku akale, monga mabuku a Ibrahima ndi
Musa.
Surat Al-A <la LXXXVII
M' dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Lemekeza dzina la Mbuye
wako Wapamwambamwamba
(ndikuliyeretsa Ku zinthu
zosayenera). 1
', •>;«■*; .:
Q
^i<*^U-
-&
^ C, $Jpl£
1 Tanthauzo lakulemekeza dzina la Mulungu ndiko kukhulupirira kuti lye
ndiwopatulika ku mbiri zilizonse zolpa zosamuyenera, monga kumufaniza
Surat 87. Al-A'la
Juzu 30
1351
>>i
AV J*H\ 5jj-
2. Amene adalenga (chilichonse)
Ndikuchikonza bwinobwino
(Mkalengedwe kolingana);
3. Amene adalamuliratu
(chilichonse Zochita zake) ndi
kuchiongolera; 1
4. Ndi Yemwenso akumeretsa
msipu;
5. Ndipo nausandutsa kukhala
wouma Ndi wodera.
6. Tikulakatulira (chivumbulutso
Chathu) ndipo suyiwala.
7. Kupatula chimene wafuna
Mulungu (Kuti uchiiwale); Ndithu,
lye Amadziwa zoonekera ndi
zimene Zimabisika.
8. Ndipo tikufewetsera (njira
*> \ '< ft?
®(S3**3^(J$\
%aMWi
ndizolengedwa; monga kuti anabereka kapena adaberekedwa, kapena kuti ali
ndi mkazi kapenanso kuti alipo omwe amathandizana naye pa umulungu Wake.
1 Mulungu pambuyo polenga zolengedwa Zake.sadangozileka kuti zisadziwe
chochita, koma cholengedwa chilichonse adachilamuliratu kuti chichite
zoyenera nacho, ndipo pambuyo pake adachiongolera pa chinthu
chimenecho; chidadziwa, ndipo chidachita.Munthu a damusonyeza zomwe
zili ndi mazunzo mkati mwake kuti adzitalikitse nazo ndiponso adamusonyeza
zabwino kuti azichite.
2 Mneneri Muhammad (SAW) adali munthu monga anthu ena ndipo adali ndi
mbiri zonga anthu adalinazo, monga: kukonda ndi kusakonda, kuiwala ndi
kukumbukira. Padapezeka kuti nthawi ina adaiwala ndi kupemphera maraka
atatu m'swala ya maraka anayi. Pachifukwa ichi pa nthawi yovumbulutsidwa
Qur'an ndi Jibril, adali akubwereza bwereza mawu ovumbulutsidwawo kuopa
kuti angaiwale. Choncho, apa Mulungu akumuletsa kuti asadzivutitse
kumabwerezabwereza mawuwo pamene akuvumbulutsidwa ndipo
adamupatsa lonjezo nthawi yomweyo kuti sadzaiwala. Ndipo adakwaniritsa
lonjezo Lake. Mtumiki (SAW) adali kumtsikira ma surah a ataliatali ndipo
amatha kuwawerenga (molakatula) popanda kuonjezera kanthu kapena
kuchepetsa, ngakhale kuti iye sadali kudziwa kuwerenga ndi kulemba.
Kuwerenga kwake kudali kwakungolakatula pa mtima.
Surat 87. AI-A<
Juzu 30
1352
>><
AV J*H\ 5j>*>
Yochitira zinthu) zabwino. 1
9. Akumbutse (wanthu
powalalikira) Ngati kukumbutsa
kuthandiza. 2
10. (Palibe chikaiko ulalikiwo)
Aukumbukira (ndikuthandizidwa
Nawo) amene akuopa Mulungu,
11. Ndipo wamavuto ambiri,
(Wamakani ndi wokanira),
adzitalikitsa ndi ulalikiwo. 3
12. Amene adzalowa ku moto
waukulu (Umene wakonzedwa
kuti udzakhale Malipiro ake);
W*2vti&
AWlM"
1 Tanthauzo la 'kufewetsa' ndiko kuti Shariya ya Chisilamu (malamulo)siili
yovuta kuyikwaniritsa monga momwe adalili malamulo a zipembedzo zoyamba.
Ndipo ndi malamulo othandiza anthu onse, nthawi zonse ndi pamalo paliponse.
2 Tanthauzo la apa sikuti Mtumiki (SAW) alalikire pokhapokha waona kuti
ulalikiwo uthandiza ayi, koma alalikire ndithu kaya kulalikirako kuthandiza
kapena ayi, monga momwe zalongosolera aya zotsatirazi. Kulankhula kotere,
Arabu amakutcha "iktifa."
3 "Wamavuto ambiri" apa, ndiko kuzunzika ndi matsoka. Mulungu akumutcha
kafiri kuti "Wamavuto ambiri" chifukwa chakuti ali ndi mavuto padziko lino
lapansi mpaka pa tsiku lomaliza. Mazunzo a tsiku lomaliza monga momwe
tidziwira ndi chilango cha moto chomwe chikumuyembekeza. Tsono "chilango
cha padziko lapansi" ndiko kuti alibe chinthu chomutonthoza likampeza tsoka
kapena vuto lililonse. Msilamu likampeza vuto amadzitonthoza ndi chikhulupiriro
chake chakuti moyo wa munthu suwonjezeka ndiponso suchepa, ndikuti
munthu amamwalira akamaliza moyo wake. Koma kafiri saganiza choncho;
amangokukuta zala ndi kuwatukwana ma dokotala kuti sadziwa kanthu
akadachita mwakutimwakuti munthuyo sakadafa. Msilamu kukampeza kusauka
amadzitonthoza ndi kupilira pamodzi ndi chikhulupiriro choti "chilichonse
chimachitika mchifuniro cha Mulungu.," Ndipo amakhala woyembekezera kuti
lero kapena mawa, Mulungu amupatsa chisomo Chake. Koma anthu opanda
chikhulupiriro amangoona kuti aponderezedwa; amayetsetsa kufunafuna chuma
mnjira zosayenera, ndipo akalephera amadzudzula uyu kapena kumenyana ndi
uyu.ndipo amangodziona ngati wonyozeka kwambiri pa maso pa munthu wolemera.
Kotero kuti atauzidwa kuti amulambire wolemera uja kuti amupatse
ndalama,akhoza kuchita zotero. Ndipo tsiku lililonse njiru imamuondetsa;
mwina amangodzipha monga momwe tionera masiku ano. Palibe mazunzo
wakulu kuposa amenewa. Ngati muyang'ana ma ayah 16 ndi 17 muona kuti
akuthirira umboni pa zimene talongosolazi.
Surat 87. Al-A'la
Juzu30| 1353 |r»*>t Mj*H\ijy*
13. Ndipo sakafa m'menemo
(ndikupumula kumazunzo),
ndiponso Sakakhala ndi moyo
(wamtendere).
14. Ndithu, wapambana amene
Wadziyeretsa (ku machimo), 1
15. Ndikukumbukira dzina la
Mbuye Wake (ndi mtima wake, ndi
lirime Lake) uku akumapemphera.
16. Koma inu mukonda
kwambiri moyo Wa dziko lapansi,
17. Pamene moyo wa tsiku
lomaliza Ndi wabwino kwambiri
ndiponso Wa muyaya.
18. Ndithu, izi (mukuuzidwa
m'Qur'an) Zilipo m'mabuku
oyamba, akale,
19. Mabuku a Ibrahim ndi Musa.
*&8%&>Z&
tfts&Fte
®i^ip^%
1 Tanthauzo lake ndikuti amene wadziyeretsa posiya kumuphatikiza Mulungu
ndi zolengedwa ndi kumchimwira ndi machimo onse. Machimo amaletsa
ulaliki wabwino kulowa mumtima wa munthu. (yang'anani ndemanga ya 14
mu surat ya Mutaffifyn)
2 Mawu akuti "wapambana amene wadziyeretsa ndi kumkumbukira Mbuye
wake ndi kumapemphera", ndiponso kuti " tsiku lomaliza ndilabwino kuposa
dziko lapansi" mawuwa adanenedwanso m'mabuku oyamba; sikuti Qur'an
ndiyo yayamba kunena zimenezi.
Surat 88. Al-Ghashiyah Juzu 30
1354
►J*-'
A A 4-J»ttJl l^yM
F
WV #L ^SURAT AL GHASfflYAH LXXXVIH
saga®^.
Surayi yayamba ndi malankhulidwe okometsa mmakutu
nkhani ya tsiku la Kiyama ndi zimene zidzachitike pa tsikulo.
Ikulozera kuti tsikulo anthu adzakhala mmagulu awiri: gulu Una
silikalandiridwa ndi ulemerero, ndipo likalowa ku moto
wotentha, pomwe gulu lina likalandiridwa mwa chisangalalo ndi
maonekedwe a mtendere omwe lidakonzedwera.
Kenako surayi yatchula zisonyezo zoonekera poyera
zosonyeza mphamvu ya Mulungu youkitsira anthu mmanda
monga momwe akuonera ndi maso awo, zopanga zake
zazikuluzikulu zimene zisonyeza kuti amene adatha kupanga
zimenezo sangalephere kuukitsa akufa.Ndipo patsogolo pake
surayi ikulamula Mneneri (SAW) kuti akumbutse anthu,
chifukwa kukumbutsako ndiwo udindo wake waukulu kwa
anthu. Udindo wake iye ndikukumbutsa kokha, osati
kukakamiza anthu chikhulupiriro. Koma yemwe adzanyozera
ndi kukanira atakumbutsidwa, Mulungu adzamlanga pamachimo
ake ndichilango chachikulu pamene adzabwerere kwa Iye
akamwalira. Chifukwa onse kobwerera kwawo nkwa Iye basi.
Ndipo onse adzaweruzidwa ndi Iye.
Surat Al-Ghashiyah LXXXVIII
m^m
q^#i(^jJt<&W-
'^te^** 9 *'
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Kodi yakudzera,(iwe
Mtumiki) (SAW) Nkhani (ya
Kiyama) imene idzaphimba Anthu
ndi zoopsa zake?
2. Nkhope zina tsiku limenelo, ®%£&^ 9 $t*J>
Zidzakhalazonyozeka, 1 4 *
1 Tanthauzo la nkhope apa ndi eni nkhopezo. Amene akunenedwa pamenepa
Surat 88. Al-Ghashiyah Juzu 30 1355 T * *>» AA a-S»^ h*>
3. Zogwira ntchito yotopetsa
Kwambiri,
4. Zikalowa ku moto wotentha
Kwambiri,
5. Zikamwetsedwa pa kasupe
Wotentha kwabasi.
6. Sadzakhala ndichakudya
koma minga,
7. Yosanenepetsa (thupi)
ndiponso Yosathetsa njala.
8. Nkhope zina tsiku limenelo
Zidzakhala zosangalala.
9. Zidzakondwera ndi malipiro
A zochita zake (za padziko
lapansi), 1
10. M'minda ya pamwamba
(Jannat):
11. Sizikamva m'menemo mawu
oipa, (Otukwana ndi kulaula),
12. Mmenemo muli a kasupe
oyenda (Mokongola). 2
13. Mmenemo muli mabedi a
pamwamba,
S'.»«ri>
h 9 fi 9 9.19 * < S ? 9 h$
<^L»V^-ouJ,
©^ "-'^
ndi anthu oipa. Mulungu watchula nkhope chifukwa ndi chiwalo cholemekezeka
pa chilengedwe cha munthu ndipo ndi pamene pali chithunzi chake.
1 Tanthauzo la "kukondweretsedwa ndi zochita zawo" ndikuti anthu abwino
adzakondwera ndi ntchito zawo zabwino zomwe adazichita pa dziko lapansi
akadzakhala ndi malipiro abwino pa tsiku lomaliza.
2 (Ndime 12-16) Zosangalatsa zentzeni za tsiku lomaliza monga momwe
adatiuzira Mneneri (SAW) kuti ku Jannah kuli zinthu zimene diso
silidapenyepo ngakhale khutu silidamvepo ndipo sizidapitepo m'maganizo a
munthu. Choncho zokondweretsa izi zimene Mulungu watiuza apa
akungofanizira ndi zinthu zomwe tikuzidziwa.
Surat 88. Al-Ghashiyah Juzu 30 1356 T ♦ >>»
A A ibUll 5jj-»
©
14. Ndi zikho zoikidwa bwino
(Pamaso pawo),
15. Ndi misamiro yoikidwa
bwino M'mizeremizere
16. Ndi mphasa (zamtengo
wapatali, Carpet) zoyalidwa
ponseponse.
17. (Kodi akunyozera
kulingalira Zisonyezo za
Mulungu), Sakulingalira
kungamira idalengedwa Motani? 1
18. Ndi thambo (limene
akuliona Nthawi zonse) m'mene
lidatukulidwira (Kutali popanda
mzati)?
19. Ndi mapiri momwe
adakhazikitsidwira (Molimba)?
20. Ndi nthaka momwe
idayalidwira
21. Basi, kumbutsa (anthu)
ndithu, Iwe, ndiwe Mkumbutsi.
22. Sindiwe wokakamiza anthu
(kuti Akhulupirire
ndikuwapondereza); 2
1 (Ndime 17-20)Mulungu akuwauza kuti ayang'ane chilengedwe cha ngamira,
thambo, mapiri ndi nthaka. Pambuyo pake alingalire, aone kuti amene
adalenga zimenezo ngotha kuchita chilichonse monga kuukitsa anthu
m'manda. Cholinga cha Mulungu potchula zinthu zimenezi, ngakhale kuti
malangizowa nga munthu aliyense, koma adali kuwauza akafiri a pa Makka
amene zinthu zimenezi maso awo ankaziona nthawi ndi nthawi.
2 Ayah iyi ikukwana kuwatsutsa adani a Chisilamu amene akunena kuti,
"chipembedzo cha Chisilamu chidafala ndi lupanga." Kutanthauza kuti
ankawakakamiza anthu kuti achivomere chipembedzochi. Sichodabwitsa
kuona adani a Chisilamu akuchinyoza chipembedzochi, koma chodabwitsa
±>%s,99' * 1///;
§s#3?&aiais
Surat 88. Al-Ghashiyah Juzu 30 1357 r * *>i
A A 4~ittJt *jj~4
23. Koma amene anyoza ndi
kukanira (Ulaliki wako),
24. Mulungu amulanga
chilango Chachikulu.
25. Ndithu, kobwerera kwawo
ndi Kwa Ife basi;
26. Ndipo ndithu,
kuwerengedwa Kwawo kuli kwa Ife.
nchakuti mawu onamawa nkumatulukanso mkamwa mwa anthu omwe
amadzitcha kuti ndi Asilamu. Nzoona alipo ena mwa anthu odziwa za
chipembedzo (ma Ulama) amene adanena kuti chipembedzo cha Chisilamu
chidatetezedwa ndi lupanga.koma simonga momwe akutanthauzirira adani
amene sadziwa za Chisilamu nkumangotsatira mabodza akuluakulu awo.
Cholinga cha ma Ulama ponena kuti "Chisilamu chidatetezedwa ndi lupanga"
kumeneko ndi kudziteteza kwa adani omwe adafuna kuchithetsa, osati
kuwakakamiza anthu kulowa mchipembedzo. Kukakamiza anthu kulowa
mChisilamu nkosaloledwa. Amene akudziwa mbiri ya Chisilamu ngakhale
pang'ono, akudziwa kuti Asitamu sadalamulidwe kuchita Jihad mpaka
pamene akafiri adafi kuwazunza. Pali nkhani zambiri za Maswahaba (otsatira
Mneneri) (SAW) ku Madina pamene adafuna kuwakakamiza ana awo kulowa
m'Chisilamu, koma Mneneri adawakaniza kutero. Basi, munthu amene
akunena zoterezo mwina akutero pa chifukwa chosadziwa za chipembedzo
cha Chisilamu, mwinanso nkukhala misala basi.
Surat 89. Al-Fajr Juzu 30 1358
*>'
A^ yjiiJl Qjj~i
Surayi yayamba ndi kulumbira komwe kwasonyeza zolinga
zosiyanasiyana zomwe zitembenula maso kuti aone mphamvu
za Mulungu pa zimenezi potsimikiza kuti amene akukana
Mulungu ndikutsutsa za kuuka, adzalangidwa monga momwe
adalangidwira omwe adatsutsa kale. Ndiponso surayi
ikufotokoza machitidwe a Mulungu poyesa anthu Ake ndi
zabwino ndiponso zoipa. Ndikuti kupereka Kwake ndi kumana
Kwake sikusonyeza chikondi Chake ndi nkwiyo Wake. Ndipo
surayi ikunenetsa za msulizo ndi umbombo womwe anthu ena
ali nawo. Kenako ikumalizira ndi kulozera za anthu osalabadira
kuchita zabwino kuti adzalakalaka akadatsogoza zochita
zabwino kuti zikawapulumutse ataona zoopsa kwambiri za
tsiku la Kiyama. Ndikuti kudzakhala kuusangalatsa mtima
wabwino wolungama umene udatsogoza ntchito zabwino,
powuitanira kukalowa ku Jannah ya Mulungu pamodzi ndi
anthu abwino.
Surat Al-Fajr LXXXIX
^ IMW^ \[
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Ndikulumbirira kuyera kwa
M'bandakucha; (pamene usiku
Uthawa),
2. Ndi masiku khumi (a Mwezi
wa Dhul-Hijja omwe ngopatulika
kwa Mulungu), 1
o^t^l^W-
-£>
sm
Tanthauzo la aya iyi ndi masiku khumi oiemekezeka omwe ali mkhumi
loyamba la mwezi wa Dhul-Hijja umene ndi mwezi wa 12 pa kalendala ya
Chisilamu. Amenewa ndi masiku oiemekezeka kuposa masiku onse ngakhale
masiku a Ramadhan kupatula usiku wa LAILA-TUL-QADR, ndi masiku khumi
Surat 89. Al-Fajr Juzu 30 1359 T • *>»
A^ j*l&\ ojy
3. Ndi Shaf i ndi Witri: (nambala
Yogawika ndi yosagawika), 1
4. Ndi usiku pamene ukupita
(Chifukwa cha kuyenda kwa dziko
Kodabwitsa).
5. Kodi m'zimene zatchulidwazi
Simuli kulumbira kokwanira, Kwa
munthu wa nzeru?
6. Kodi sudadziwe momwe
Mbuye wako Adawalangira Adi
(anthu A Mneneri Hud).
7. Aku Irama; ataliatali ngati
Zipilala. 2
8. Omwe onga iwo
sadalengedwe M'maiko ena?
9. Ndi Asamudu, (anthu A
Mneneri Swaleh) amene adali
Kudula matanthwe ku chigwa
(Chotchedwa Wadi Qura ndi
kumamanga Nyumba
zikuluzikulu)?
10. Komanso Firiauna (Farawo)
Mwini magulu ankhondo (omwe
Amalimbikitsa ufumu wake monga
Momwe zichiri zimalimbikitsira
Tenti),
%$\#^\&&&%i>j
e$j$\(S2&&
omaiiza a mwezi wa Ramadhan. Choncho ndi bwino kuchulukitsa
mapemphero m'masiku amenewa.
1 Shaf i ndi nambala yotheka kugawa ndi 2 (even number) Witri ndi nambala
yosatheka kuigawa ndi 2 (odd number). Cholinga cha Mulungu pamenepa ndi
kuzilumbirira zinthu zonse zimene adazilenga, zowerengedwa mnjira zonse ziwiri.
2 (Ndime 7-9) Adi aku Irama ndi mtundu wa Mneneri Hud. Adali akuluakulu
matupi a mphamvu kwambiri mwakuti ankanena kuti, "Ndani wamphamvu
kuposa ife!" Thamudu (Samudu) ndi mtundu wa Mneneri Swaleh. Iwowa adali
kukhala ku mpoto kwa chilumba cha Arabia.
Surat 89. Al-Fajr Juzu 30 1360 T * *>»
A^ >*iJi $jj~*
11. Amene adaipitsa m'maiko
mopyola Malire?
12. Ndipo adachulukitsa
m'menemo Kuononga (pamwamba
pakuononga). 1
13. Choncho Mbuye wako
adawathira Ndi mitundu ya zilango
(zoopsa)
14. Ndithu, Mbuye wako ali
tcheru (ndi Zochita za anthu.
Ndipo Akuwasungira kuti
adzawalipire). 2
15. Pamene munthu Mbuye
wake akumuyesa (Mayeso)
ndikumulemekeza ndi Kumpatsa
mtendere (wachuma, Ulemerero
ndi mphamvu) amanena Monyada:
Mbuye wanga wandilemekeza
(Chifiikwa zimenezi nzondiyenera
ine).
16. Koma akamuyesa mayeso
ndi kumchepetsera Riziki lake,
(chuma) amanena (motaya mtima):
Mbuye Wanga wandinyoza!
17. Sichoncho ayi, (monga
momwe mukuganizira) koma inu
simuchitira za Ufulu ana amasiye!
18. Ndipo simulimbikitsana za
Kudyetsa osauka,
^\&$$&&
&$&\JX&&1&$1
©,
1 Mzinthu zoipa zimene Farawo adachita, ndi kudzitcha kuti iye ndi Mulungu,
kupha ana achimuna popanda chilungamo, ndi kuwazunza Aisraeli.
2 Apa ndikuti Mulungu akuwaona anthu Ake nthawi ili yonse. Palibe chimene
iwo achita popanda lye kuchiona ndi kuchilemba.
Surat 89. Al-Fajr Juzu 30 1361 T * *>»
AS j*d\ 5jj-
19. Ndipo mukudya chuma cha
masiye; Kudya kosusuka. 1
20. Ndiponso mukukonda
chuma; Kukonda kopyola muyeso.
21. Sichoncho! (Siyani
machitidwe Amenewa); nthaka
ikadzapondedwa Pondedwa
(ndikuifafaniza),
22. Adzabwera Mbuye wako
(mmabweredwe Omwe
akuwadziwa iye mwini) Ndipo
angero ali mmizere
Yondondozana.
23. Basi tsiku limenelo
idzabweretsedwa Jahannamu, pa
tsiku limenelo Munthu
adzakumbukira, koma kukumbuka
Kumeneko kudzamthandiza
chiyani?
24. Adzanena: Kalanga ine!
Ndikadatsogoza zabwino pa Za
moyo wangauno!
25. Motero patsikuli, palibe
wina Amene adzalange monga
momwe (Mulungu) adzalangire. 3
26. Ndiponso sanganjate
aliyense Monga kunjata kwa iye
(Mulungu).
1 Arabu asadalowe m'Chisilamu akazi sadali kugawiridwa chuma cha masiye
kudzanso ana aang'onoang'ono a masiye sadali kuchiona chumacho
2 Tanthauzo la "kubweretsedwa Jahanamu" ndiko kuisonyeza kwa anthu.
3 (Ndime 25-26) Tanthauzo lake ndikuti palibe chofanizira chilango cha
Mulungu chomwe chidzaperekedwe kwa akafiri ndiponso ndi kunjata komwe
akafiri adzanjatidwe.
Surat 89. Al-Fajr Juzu 30
1362
r* *>i
A^ j*iJl 5jj-*»
27. Ee! Iwe mzimu
wokhazikika (ndi Choona)! 1
28. Bwerera kwa Mbuye Wako
uli wokondwera(ndi zomwe
Wapatsidwa), ndipo uli
woyanjidwa (Ndi Mulungu pa
zomwe udatsogoza). 2
29. Lowa mgulu la akapolo
anga abwino,
30. Ndipo lowa m'munda
wanga (mnyumba ya Mtendere wa
muyaya).
Sfc£]tflJ3SlRg3S
e^&m
L, 4 '_,&>£
SURAT AL-BALAD XC
Mulungu walumbirira mzinda wopatulika wa Makka, kwawo
kwa Mtumiki (SAW) kumene adakulira ndiponso walumbirira
wobereka ndi woberekedwa. Kudzera mwa iwo udasungidwa
mtundu wa anthu, kuti ndithu, munthu adalengedwa mmavuto.
Kenaka Mulungu wafotokoza kuti munthu ali wonyengedwa
pomaganizira kuti palibe amene angamchite kanthu ndikuti iye
ngwachuma chambiri. Ndipo kenako Mulungu watchula zina
mwa zomwe wamdalitsa nazo monga,kumfewetsera njira kuti
akakhale mmodzi wa anthu a ku Jannah, anthu a kumanja.
1 "Mzimu wokhazikika" ndi mzimu wa munthu wokhulupirira amene akuchita
zomwe walamulidwa ndi kusiya zimene waletsedwa. Umenewo ndiwo mzimu
umene udzakhale wodekha pa tsiku lomaliza chifukwa chakuti pa tsikulo
sudzakhala ndi mantha kapena kudandaula.
2 Tanthauzo lake nkuti mzimu wokhazikika udzakondwera ndi zimene
udzalandira kwa Mulungu tsiku limenelo ndipo naye Mulungu adzakondwera
nawo.
Surat 90. Al-Balad Juzu 30
1363
r. *>-i
^ • jULJi hjy~>
Surat Al-Balad XC
mm
Qfa&\<&$Wj
©oJi^lvjJtj
®£$&w&&
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Ndikulumbirira mzinda uwu
(Wa Makka),
2. Ndipo iwe udzatsikira mu
Mdzindawu mwa ufulu (ndi
Kuuonjezera ulemelero).
3. Ndiponso ndikulumbirira
Chobereka ndi choberekedwa,
(Kudzera mwa iwo mtundu wa
Anthu udasungidwa);
4. Ndithudi tamulenga munthu
mmavuto (Kuyambira chiyambi
chake Mpaka malekezero a moyo
wake). 1
5. Kodi (munthu wolengedwa
ndi Mavutoyu) akuganiza kuti
palibe Amene angamuthe?
6. Akunena (monyadira kuti):
"Ndaononga chuma chambiri
(Chifukwa choletsa Chisilamu
kufala)." 3
Munthu ali ndi mavuto ambiri amene nyama zina zilibe: chakudya
amachipeza movutikira, ndipo kudya kwa iye nkofunikira pa moyo wake,
chovala amachipeza movutikira pomwe iye ndiwoyenera kuvala. Sangathe
kupirira ndi kutentha kapena kuzizira. Sangathenso kudziteteza popanda
chida. Ndipo pamwamba pa izi, Ambuye Mulungu amukakamiza zinthu
zambiri ndi kumuletsanso zinthu zambiri. Ndipo chilichonse chimene iye
achita chikulembedwa. Pa tsiku lomaliza adzawerengedwa chilichonse
chimene adachichita; chachikulu kapena chaching'ono.
2 Tanthauzo lake apa nkuti munthu akuganiza kuti palibe aliyense amene
angamuweruze pa zolakwa zake.
3 (Ndime 6-7) Mawu awa akunenedwa kwa okanira omwe adali kupereka
Surat 90. Al-Balad Juzu 30
1364
►>'
^ * jJLJl 5jj-»
7. Kodi akuganiza kuti palibe
Akumuona?.
8. Kodi sitidampangire maso
Awiri (amene akuyang'anira)?
9. Ndilirime ndi milomo iwiri
(Zimene akulankhulira)?
10. Ndipo tamlongosolera njira
ziwiri: (Yabwino ndi yoipa, ndipo
Tampatsa mphamvu yosankhira
Njira imene akufuna).
11. Kodi walikwera phiri lovutalo
(lomwe lingakamfikitse ku Jannah)? 1
12. Nanga nchiyani
chakudziwitsa za Kukwera phiri
lovutalo?
13. (Kutero ndiko) kupereka
ufulu kwa Kapolo,
14. Kapena kuwadyetsa
(osowa) pa Masiku a njala,
15. Amasiye achibale (ndi
amene Sali achibale),
16. Kapena wosauka wa fumbi
Lokhalokha (chifukwa cha
kuvutika Kwambiri),
chuma chawo pomenyana ndi Usilamu kapena kufuna kumupha Mneneri
(SAW). Kenako adali kudzitama chifukwa chopereka chuma chambiri pa njirayo.
Izi zikumukhudza aliyense amene akufuna kuti Chisilamu chionongeke.
Ndipo iwo amaganiza kuti Mulungu sakudziwa za maganizo awo oipa.
1 Tanthauzo lake ndikuti bwanji munthu sathokoza chifundo chimenechi
(chopatsidwa maso ndi pakamwa) pogwiritsa ntchito chuma chake pa zinthu
zabwino zimene Mulungu wazitchula m'ma aya akubwerawa? Ndipo
tanthauzo la "kukwera phiri lovuta" ndiko kupereka chuma panjira ya Mulungu
chimene chili ndinthu chovuta kwa anthu ambiri ndipo chimafanana
ndikukwera phiri losongoka .
Surat 90. Al-Balad Juzu 30
1365
r% *j*-i
^ • jJUl Sjj--
17. Komanso nakhala mmodzi
Mwa okhulupirira
ndikumalangizana Za
kupirira,ndiponso za chifundo.
18. Otero ndiwo (anthu abwino)
A ku dzanja lamanja.
19. Koma amene
sanakhulupirire aya Zathu, ndi
anthu a kudzanja Lamanzere
(oipa).
20. Moto wozungulira mbali
zonse Udzakhala pa iwo
(ndikuwatsekera Makomo).
SURAT ASH-SHAMS XCI
Mulungu walumbirira zinthu zambiri mzolengedwa Zake
zazikuluzikulu koyambirira kwa surah iyi zomwe zikusonyeza
kukwanira kwa mphamvu Zake ndi umodzi Wake potsimikiza
kuti wapambana amene wayeretsa mtima wake ndi
chikhulupiriro chake ku uchimo ndi kumvera Mulungu.
Ndiponso kuti wataika amene waudetsa ndi machimo ndi
kukanira Mulungu. Kenako surayi yafotokoza nkhani ya
Asamud omwe adali anthu a Swaleh ndi zimene zidawatsikira
kuti aliyense wa makani ndi wotsutsa aphunzire kupyolera mwa
iwo.
Iwo pamene adamkanira Mneneri wawo ndikupha ngamira
yoletsedwa, Mulungu adawaononga onse.Iye Mulungu saopa
kanthu pazotsatira zakuwaononga kwawo, chifukwa lye
safunsidwa zimene akuchita. Adawatsitsira chilango
choyenerana ndi makhalidwe awo oipa.
Surat 91. Ash-Shams Juzu 30 1366 ? • *>»
^ ) ^w Jl 3jJ-J
Surat Ash-Shams XCI
■**■
g^US^
o^l^jll^U-
-£>
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Ndikulumbirira dzuwa ndi
Dangalira lake,
2. Ndi mwezi pamene
ukulitsatira (dzuwalo Ndikulowa
mmalo mwake powalitsa Litalowa),
3. Ndi usana pamene ukulisonyeza
Poyera (kuti lisaphimbidwe),
4. Ndi usiku pamene ukuliphimba,
5. Ndi thambo ndi (Mwini
mphamvu ZonseWamkulu) yemwe
adalimanga Ndikulitukula
(mwaluso),
6. Ndi nthaka ndi(Mwini
mphamvu zonse Wamkulu),
yemwe adaiyala (mbali Zonse
ndikuchita kukhala ngati Choyala),
7. Ndimzimu ndi yemwe
adawulinganiza (poupatsa
mphamvu);
8. Ndipo adaudziwitsa zoipa zake
ndi Zabwino zake: (ndikuupatsa
ufulu Ndi mphamvu zochitira
zimene Ukufiina).
9. Ndithu, wapambana amene
wauyeretsa. 1
1 Kuyeretsa mzimu ndiko kuukongoletsa ndi maphunziro ndi ntchito zabwino.
Zimenezi ndizo zimamkwanitsa munthu kuti atchulidwe munthu. Ndipo zimenezi
ndizo zingapereke ulemerero kwa munthu pa dziko mpaka pa tsiku lomaliza.
<^c^(j^-£l!S
£>14*& %&™3
\£^^t&3\j
©t^Uj^S'b
Surat 91. Ash-Shams Juzu 30
1367
.jA-i
^ ) j^gJtJl 5jj-*»
"ite^lU
^i&^i&SjtfJOSi
©I
*fl-**J
10. Ndipo ndithu,wataika
amene Wauononga. 1
11. Thamud (Samudu) adakanira
(Mneneri wawo) chifukwa cha
Kulumpha malire kwawo. 2
12. Pamene woipitsitsa wawo
Adadzipereka (kupha ngamira
Yozizwitsa).
13. Pamenepo Mneneri wa
Mulungu (Swaleh) adawauza:
"Isiyeni ngamira ya Mulungu (Idye
mdziko la Mulungu). Musailetse
kumwa madzi (pa Tsiku lake).
14. Koma adamutsutsa ndikuipha;
kwa Chifukwa chimenecho Mbuye
wawo (Mulungu) adawaononga
chifukwa Cha tchimo lawo;
adangowafafaniza (Onse mnthaka).
15. lye saopa zotsatira za
chilangochi (Chifukwa amenewa
ndi malipiro A chilungamo pa
zomwe adachita).
Kuwuononga mzimu ndiko kuuchitira mphwayi; kungoulekerera
ndikumautsatira pa zimene ufuna mpaka kulowa mu uve ndi m'machimo a
umbuli ndipo ndi kuonongeka pa dziko lino mpaka Pa tsiku lomaliza.
2 (Ndime 11-15) Asamudu atchulidwa m'surat AL-FAJR. Anthu awa
adamukana Mtumiki wawo, Mtumiki Swaleh (AS); adamuuza kuti ngati afuna
amukhulupirire, atulutse ngamira kuchokera mthanthwe, apo ndipo
adzamukhulupirira kuti ndi Mneneri. Swaleh adampempha Mulungu, ndipo
lidasweka thanthwe lija ndikutulukamo ngamira monga momwe adafunira
anthu aja. Koma sadamukhulupirirebe.
Mneneri Swaleh (AS) adawauza kuti:"Chenjerani ndi ngamira ya Mulungu iyi,
musaikhudze ndi choipa chilichonse." Ndipo adawakakamiza kuti pa tsiku
limene ngamira ija ikumwa madzi, iwo asatunge madzi. Ndiponso pa tsiku
limene iwo akutunga madzi.ngamira siidzamwa madzi. Koma adamkanira.
Ndipo m'modzi wa iwo amene adali wamphulupulu adaipha ngamira ija.
Mulungu nthawi yomweyo adawatsitsira chilango chifukwa cha machimo awo,
chomwe chidawakwanira onse kuyambira uja wopha ngamira ndi ena onse.
® <jt^<J>Qyj
Surat 92. Al-Lail
Juzu 30
1368
,>i
*Y JJUlJjj-
Mulungu wolemekezeka akulumbirira zinthu zitatu msurah
iyi, potsimikiza kuti ntchito za anthu nzosiyana: zina
nzolungama pomwe zina nzosalungama. Ndikuti amene
akupereka za ulele, ndi kuopa Mulungu ndikuikira umboni
mwachilungamo pazinthu zabwino, Mulungu amfewetsera njira
zabwino. Ndipo amene wachita umbombo ndikuziganizira kuti
ngoima payekha ndikumatsutsa mawu abwino, Mulungu
amfewetsera njira zopita kumavuto. Ndipo chuma chake
sichidzamthandiza kumchotsa mmavuto, akadzafa.
Ndipo kenaka surayi ikufotokoza kuti Mulungu ndiye mwini
udindo wolongosolera anthu njira ya chiongoko. Ndikuti moyo
watsiku lomaliza ndi moyo wadziko lapansi ngwake. Ndiponso
yachenjeza za chilango cha moto chomwe anthu oipa
akalangidwa nacho pomwe abwino akapulumuka.
Surat Al-Lail XCII
oi^lt^ll^
-^
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Ndikulumbirira usiku
pamene Ukuphimba (chilichonse),
2. Ndi usana pamene kukuyera,
3. Ndiponso Yemwe adalenga
Chachimuna ndi chachikazi,
4. Ndithu, zochita zanu
nzosiyanasiyana. l
1 Tanthauzo lake ndikuti mwa anthu alipo ena amene amachita zabwino ndipo
ena amachita zoipa. Ena amagwira ntchito zothandiza pambuyo pa imfa pamodzi
ndi kutumikira Mulungu. Ndipo pali ena omwe amangokhala otanganidwa ndi
zadziko lapansi. Ena amachita zinthu zopindula pomwe ena satero.
W;;#ji#a:
••
<2V&^"-
0\
Siirat 92. Al-Lail
Juzu 30
1369
r* *>t
S Y JJLi* 5jj-
5. Tsono yemwe akupereka (pa
njira Ya Mulungu) ndikumamuopa
(Mbuye Wake ndikupewa
zoletsedwa), 1
6. Ndikumavomereza zinthu
zabwino; (Komwe kuli
kukhulupirira Mulungu
Mwanzeru), 2
7. Timufewetsera njira
yompititsa ku zabwino. 3
8. Koma uyo achite umbombo
ndikuganiza Za kuti iye payekha
ngokwana;
9. Ndi kumatsutsa zinthu
zabwino,
10. Timufewetsera njira
yompititsa Ku mavuto (a muyaya).
11. Chumachake
sichidzamthandiza (Chilichonse)
akadzagwera ku moto.
12. Ndithu, Ife ndi amene
timawalongosolera Anthu njira
yabwino ndi njira yoipa.
13. Ndipo ndithu, moyo
womaliza ndi Moyo woyamba uli
m'manja mwathu.
ajsijcWSfc
A ) 9 9 9 \ l 9v'9"<
1 Tanthauzo lake apa ndikupereka chuma ndi kudzipereka pa zauzimu. Ndiye
kuti munthu agwiritsire ntchito chuma chake m'njira ya Mulungu ndiponso kwa
anthu anzake. Ayeneranso kudzipereka iye mwini pa moyo wauzimu.
2 Tanthauzo la "Kuvomereza zinthu zabwino" ndiko kugwirizana nazo zimene
Mulungu walamula, chifukwa chakuti lye amalamula zinthu zabwino
zokhazokha ndikuletsa zoipa.
3 Tanthauzo la aya imeneyi ndikuti: Timufewetsera njira yochitira zinthu
zabwino mpaka kufikira kuti akapanda kuchita chinthu chabwino sapeza
mtendere mumtima mwake.
Surat 92. Al-Lail Juzu 30 1370 T * *>»
M JJJio^
14. Basi, ndikukuchenjezani za
Moto woyaka mwa mphamvu;
15. Palibe amene akaulowe
Koma (Kafiri) woipitsitsa
kwambiri,
16. Yemwe amakanira (choona)
ndi Kunyoza (zisonyezo za
Mulungu).
17. Koma yemwe akuopa
Mulungu Kwambiri
akatalikitsidwa ndi moto;
18. Amene akupereka chuma
chake Ndi cholinga chodziyeretsa.
19. Ndipo palibe aliyense Kwa
iye, amene adamchitira za
Chifundo zomwe zikulipidwa. 1
20. Koma ( akuchita zimenezi)
Kufuna chikondi cha Mbuye wake
Wa pamwambamwamba.
21. Ndipo posachedwa
adzasangalala. 2
® Jyi'v^^l
WKg^i
S (SU^oM(i^
h&$\$>&ft£
1 (Ndime 19-20)Tanthauzo la ma aya awiri awa nkuti munthu uyu sakupereka
chuma chake chifukwa chobwezera chifundo cha anthu, kapena kuti
adzamubwezerenso iye chifundo, koma akupereka chifukwa chofuna chikondi
cha Mbuye wake basi.
2 Tanthauzo lake apa ndikuti Mulungu adzamukondweretsa ndi malipiro Ake
abwino kufikira munthuyo adzakondwera. Ma aya, kuyambira 17 mpaka 21,
adatsika chifukwa cha Sayyidina Abu Bakr (RA) yemwe adali kupereka chuma
chake powagula akapolo omwe adali kuzunzidwa ndi mabwana awo chifukwa
cholowa Chisilamu, pambuyo pake amawapatsa ufulu. Ndipo m'modzi wa
iwowa ndi Sayyidina Bilal amene adali Muazzini wa Mneneri Muhammad
(SAW). Chomwechonso aya zimenezi zikumkhudza aliyense amene
akugwiritsa ntchito chuma chake mnjira yopulumutsira chipembedzo.
Surat 93. Adh-Dhuha Juzu 30
1371
T * frj£-t \T ^-iait $j>->
Surayi yayamba ndi kulumbira kuwiri kulumbirira nthawi
yogwiridwa ntchito ndi nthawi yopumula, potsimikiza kuti
ndithu, Mulungu sadasiye Mneneri Wake kapena kumuda.
Ndipo zimene wamkonzera tsiku lomaliza ndizabwino kuposa
zimene wamdalitsa nazo padziko lapansi. Kenaka Mulungu
walumbira kuti adzampatsa kufikira atakondwera monga
momwe adampezera ali wamasiye ndipo adamsunga; ali
wosazindikira Qur'an ndipo adamuongola bwino
pomuzindikiritsa Qur'aniyo; ali wosauka ndipo adamlemeretsa.
Kenako surayi ikulimbikitsa zochitira chifundo amasiye
ndikuletsa kukalipira opempha ndikutinso tikhale tikunena za
Mtendere wa Mulungu umene uli paife posonyeza kuthokoza.
Surat Adh-Dhuha XCIII
ti^l££ _ '#'
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Ndikulumbirira masana
dzuwa Litakwera (imene ili nthawi
Yantchito),
2. Ndi usiku pamene
ukuvindikira,
3. Sadakusiye Mbuye wako
(iwe Mneneri) (SAW) ndiponso
sadakude. 1
o^t^i^U-
"Wwb
1 M'masiku oyamba pa chiyambi cha Usilamu, padapita masiku angapo
Mtumiki (SAW) osamutsikira chivumbulutso. lye poona izi adali kukaika ndi
kudandaula kwakukulu, nao okanira apa Makka adali kumchita chipongwe.
Adali kumunena kuti, "kodi Mbuye wako wakusiya kapena wakukwiira?" Basi
apa Mulungu akumutonthoza Mneneri Wake, pamodzi ndi kuwayankha
okanira aja kuti, "Sadamusiye ndipo sadakwiye naye."
Surat 93. Adh-Dhuha Juzu 30
1372
r» s-jjfc-i sr ti5 iwjiii 5jj--
4. Ndithu, umoyo watsiku liri
Mkudza ndi wabwino kwa iwe
Kuposa umoyo woyambawu. 1
5. Ndithu posachedwapa
akupatsa Mbuye wako (zabwino
zamdziko Lapansi ndi tsiku
lomaliza) Ndipo ukondwera. 2
6. Kodi sadakupeze uli wa masiye
Ndipo adakupatsa pokhala pabwino?
7. Ndipo adakupeza uli
wosazindikira (Qur'an)
Nakuongola (pokuzindikiritsa
Qur'aniyo ndi Malamulo a
chipembedzo)? 3
8. Ndiponso adakupeza uli
Wosauka Nakulemeretsa?
9. Basi, wamasiye usamchitire
nkhanza..
10. Ndiponso wopempha
usamukalipire.
11. Tsono mtendere wa Mbuye
wako Uwutchule (pothokoza ndi
Kugwira ntchito zabwino).
* i -VV A *Fl
1 Ayah iyi ikulozera kuti tsiku lililonse lomwe likubwera zochita za Mneneri
zidzankerankera patsogolo. Mmenemo ndimomwe zidalili chipembedzo
chimatukuka kupita patsogolo. Ndipo
2 Zopatsidwa zomwe adalonjezedwa apa ndi Mulungu wake, ndi zapadziko
mpaka kumwamba (Akhera). Padziko lapansi adampatsa chilichonse chimene
adali kuchilakalaka monga kuwaongola anthu ake, kuchilemekeza chipembedzo
chake ndi kuwagonjetsa adani ake. Zonsezi Mulungu adamchitira mnyengo
yochepa modabwitsa.
3 Mneneri Muhammad (SAW) asanapatsidwe uneneri wake ndi Mulungu anali
kudandaula kwambiri poona anthu ake ali osokera ndiponso poona kuti iye
sadali kudziwa momwe angawaongolere. Pambuyo pake adali kumapita ku
mapiri amene adali pafupi ndi mzinda wa Makka. Kumeneko adali kupemphera
ndi kumalingalira ndi kupempha Mulungu kuti amusonyeze njira yachiongoko.
Surat 94. Ash-Sharh Juzu 30
1373
.j*
H i Cr tJl ijj*
J^ SURAT ASH-SHARH XCIV
r Lrc^zzrLKrY .w-rv^ _— _ .
Surayi ikulongosola kuti Mulungu adaphanula chifuwa cha
Mneneri (SAW) ndikuchichita kukhala potsikira zobisika ndi
maphunziro. Ndipo adamchotsera zomwe zinkalemeretsa msana
wake pantchito yolalikira. Ndipo Mulungu analumikiza dzina
Lake ndi iye pa mawu amaziko a chikhulupiriro ndi mzinthu
zina zazikuluzikulu mchipembedzo. Kenako surayi yalongosola
za machitidwe a Mulungu pophatikiza zabwino ndi zovuta,
ndipo Mtumiki akuuzidwa kuti akachita chabwino,
achitsatizenso ndi chabwino china; ndikuti cholinga chake pa
zonse chikhale kwa Mulungu. Iye ndiwakutha kumthandiza.
Surat Ash-Sharh XCIV
M' dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Kodi sitidachiphanule
chifuwa Chako (pokupatsa
chiongoko ndi Chikhulupiriro ndi
nzeru zambiri)? 1
2. Ndipo takuchotsera mtolo
Wako (pantchito yolalikira
pokuthandiza Ndi kukufewetsera
zinthu zako);
3. Mtolo umene udalemetsa
msana Wako?
4. Ndipo takukweza
kutchulidwa kwako. 2
o^ly^jM^U-
-2>
OiljOud^I^i^J I
h2^(j^\($o$\
W)^z&
1 Kuchiphanula chifuwa, kumeneko ndiko kuchotsa chikaiko choipa.
2 Mulungu wakukweza kutchulidwa kwa Mtumiki Muhammad (SAW)
pakumpatsa uneneri kumchitira zabwino kuposa aneneri ena, kuchipanga
chipembedzo chake kukhala chotsiriza chosafafanizidwa ndi Mtumiki wina.
Surat 94. Ash-Sharh Juzu 30 I 1374 T • *>»
^ £ £j-*Jl 5jj-»
5. Ndipo ndithu, pali chovuta
palinso zabwino (Zambiri).
6. Ndithu pali chovuta palinso
zabwino (zambiri).
7. Basi, ukamaliza ntchito
(yolalikira Ndi Jihad) limbikira
kupemphera. 1
8. Ndipo khala wolakalaka
(zabwino zomwe zili) Kwa Mbuye
wako.
M'surayi Mulungu akulumbirira zipatso ziwiri zodala, ndi
malo awiri abwino potsimikiza kuti lye adalenga munthu
mkalengedwe kabwino: pompatsa nzeru ndikukhala ndi ufulu
pa zofuna zake. Kenaka surayi yalongosolanso kuti munthu
sadachite motsatiza chilengedwe chake ndipo watsika pa
ulemerero wake ndikukhala wapansi kuposa wapansi, kupatula
amene akhulupirira ndikumachita zabwino.
Kenako surayi yadzudzula amene akukanira za kuuka
mmanda ataona kale zizindikiro zake zosonyeza mphamvu za
Mulungu ndi luso Lake.
Ndipo ndi chopambana kuposa zipembedzo zonse zomwe zidatsogola,
ndiponso ndi chomwe chingawathandize anthu onse osiyana mitundu, pa
nyengo zonse ndi pamalo pali ponse.
1 Tanthauzo lake nkuti, "Ukamaliza ntchito yako yolalikira kwa anthu zomwe
Mulungu wakutuma kuti ulalikire.chita mapemphero ambiri.umthokoze Mbuye
wako pa chisomo Chake chimene wakudalitsa nacho." Mneneri (SAW) adali
kulimbikira kwambiri pochita mapempheroMwakuti amaima ndi kumapemphera
kufikira miyendo yake kutupa. Amagwetsa mphumi pansi (sijida) mpaka
kuganiziridwa kuti wafa chifukwa cha kutalika kwa nthawi yopempherayo.
Surat 95. At-Tin
Juzu30 1375 r» tji-i
^0 jjl Ojj-**
Surat At-Tin XCV
~j^^
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Ndikulumbirira mitengo ya
Mkuyu Ndi Zitona (pansi pa
Mitengo Imeneyi Ibrahim ndi Nuh
(Nowa) Adapeza uneneri),
2. Ndi phiri la Sinai (pamene
Mulungu adamulankhulira Musa),
3. Ndiponso Mzinda uwu
(wolemekezeka) Wamtendere:
(Makka,womwe Adapatsiridwa
uneneri Muhammad) (SAW),
4. Palibe chikaiko, tamulenga
munthu Mkalengedwe kabwino,
kolingana (Ndipo ali ndi mbiri
zabwino); 1
5. Pambuyo pake tamubwezera
pansi Kumposa wa pansi; 2
6. Kupatula amene
akhulupirira Ndikumachita
zabwino, adzakhala Nawo iwo
malipiro osatha.
7. Tsono nchiyani chakuchititsa
kuti Ukanire kuuka ndi malipiro
o&g\uP&\&\j
^%%<$$*
0(^JtonilJ^j
®^^^p>!^(yU^lwtoual
©^OilJ^^^
1 M'gulu la nyama palibe yopambana kuposa munthu mkalengedwe ndi pa
nzeru.
2 Munthu ali ndi makhalidwe awiri: Ngati agwiritsa ntchito nzeru zake
amaongoka ndipo amaiposa nyama iti yonse. Koma ngati sagwiritsa ntchito
nzeru zake amasokera ndi kukhala wapansi kuposa nyama zonse.
Surat 96. Al-'Alaq Juzu 30
1376
*>'
^1 jUJl ijj-*
pambuyo (Poona mphamvu zathu
pachilichonse)? 1
8. Kodi Mulungu si Muweruzi
wa nzeru Kuposa aweruzi onse?
hti^P&\{$
SURAT AL- 4 ALAQ XCVI
M'surayi akutilimbitsa za kuphunzira kuwerenga ndi
kulemba. Ndikuti amene adatha kumlenga munthu kuchokera
kuchinthu chofooka angathe kumphunzitsa kulemba kuti
maphunziro asungidwe ndi kulembako: ndikuti azimvana
kupyolera mkulembako. Ndiponso ndikumphunzitsa zomwe
sadali kuzidziwa.
Surayi ikufotokozanso kuti nthawi zina chuma ndi mphamvu
zimachititsa mtima wa munthu kupyola malire.
Surat Al-'Alaq XCVI
m
o£*2l<y*f£t>iU-
-^
©^j^^lpl
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Werenga! (Iwe, Mneneri
(SAW), zomwe
Zikuvumbulutsidwa) Mdzina la
Mbuye Wako yemwe adalenga
(zolengedwa Zonse). 2
1 (Ndime 7-8) Mulungu akuuza munthu kuti: Pambuyo podziwa kuti Mulungu
ndi yemwe adapanga zimenezo, ndi chiyani nanga chikumukaikitsa za tsiku la
chiweruzo?
2 Tanena kale mndemanga 7 yamu surat - Dhuha kuti Mneneri Muhammad
(SAW) asadapatsidwe Uneneri wake ndi Mulungu adali kudandaula kwambiri
poona anthu ake ali osokera ndiponso poona kuti iye sadali kudziwa momwe
angawaongolere. Pambuyo pake adali kumapita ku mapiri amene adali
pafupi ndi Mzinda wa Makka.Kumeneko adali kupemphera ndi kumalingalira
Surat 96. Al-'Alaq Juzu 30 1377 T * fr j*-i
^ 1 jWl dj^-*
2. Adalenga munthu kuchokera
Kumagazi owundana, 1
3. Werenga! Ndipo Mbuye
wako ndi Mfulu, 2
4. Yemwe waphunzitsa
(munthu Kulemba) ndi
cholembera.
5. Waphunzitsa munthu zinthu
(Zambiri) zomwe (iye) sadali
Kuzidziwa.
6. Zoona ndithu, koma munthu
Akupyola malire (podzikweza Ndi
Mulungu wake),
7. Chifukwa chodziona kuti
walemera.
8. Palibe chikaiko, (iwe
Mneneri (SAW) Kobwerera
ndi kupempha Mulungu kuti amusonyeze njira ya chiongoko. Choncho tsiku
lina pamene adati ku phanga la Hiraa, pafupi ndi Makka ali mkati
mopemphera, Mngelo adamuonekera mwadzidzidzi nati: "Iwe Muhammad!
Ine ndine Jiburil (Gabriel) ndipo iwe ndiwe Mtumiki wa Mulungu kwa
zolengedwa zonse!" Pambuyo pake adamuuza kuti, "werenga!" Mneneri
adayankha, "Ine sindidziwa kuwerenga." Jiburil uja adamgwira ndi kumpana
mwamphamvu mpaka adavutika kwambiri. Adamsiyanso ndi kumuuza,
"werenga!" Mneneri adayankha monga adamuyankhira poyamba mpaka
kadakwana katatu akumuchita zokhazokhazo. Kenaka adamuwerengera ma
ayah kuchokera 1 mpaka 5. Ma ayah amenewa ndiwo oyamba
kuvumbulutsidwa m'Qur'an.
1 Madzi ambewu ya munthu, pambuyo pokhazikika mchiberekero kwa masiku
makumi anayt, amatembenuka ndikukhala magazi. Hi ndiio tanthauzo la ayah
imeneyi.
2 Ayah 3 ndi 5 zikukhala ngati kuti Mtumiki (SAW) akuyankhidwa pa kunena
kwake kwa kuti "Ine sindidziwa kuwerenga." Choncho Mulungu akumuuza kuti
lye ndi mfulu weniweni, ndi yemwe adawaphunzitsa anthu kulemba ndi
cholembera ndi zonse zomwe sadali kuzidziwa. Kwa ufulu Wake wochuluka
ndi mphamvu Zake pa chilichonse, sichovuta kwa lye (Mulungu)
kumphunzitsa Mtumiki Wake kuwerenga molakatula.
Siirat 96. Al-'Alaq Juzu 30 137J
t r* *j*-i ^ jWis^
(onse) nkwa Mbuye wako Basi;
(adzawaukitsa). 1
9. Kodi wamuona yemwe
akuletsa,
teiis
10. Kapolo (wa Mulungu)
akamapemphera?
11. Tandiuza ngati ali
pachiongoko.
< ^&\#&v&
12. Kapena kuti akulamulira
zoopa Mulungu?
®^i^ijj
13. Tandiuza (za woletsayo)
ngati Akutsutsa (zimene wadza
nazo Mneneri) ndikunyoza
(chikhulupiriro Ndi ntchito
yabwino)?
14. Kodi sakudziwa kuti
Mulungu Akuona (machitidwe
ake.Ndipo Adzamlipira)?
%»&;©!
15. Ayi ndithu, ngati sasiya
Timukoka tsitsi lapaliwombo;
(Tiligwira mwamphamvu liwombo
Lake ndikukamponya kumoto).
^IXfL3ll&$&$&
16. Liwombo labodza
(ndiponso) lamachimo.
fypffiiiX
17. Basi aliitane gulu lakelo,
(La amene amakhala nawo
pabwalo Kuti amthandize pano
padziko Kapena tsiku lomaliza),
1 Tanthauzo lake nkuti musanyengedwe ndi chumacho chifukwa chakuti,
popanda chikaiko, mubwerera kwa Mbuye wanu ndipo chumacho
sichidzakuthandizanl chilichonse pa maso Pake.
Surat 97. AI-Qadr Juzu 30
1379
r* «.jJrl
^V jJili Sjj~*>
18. Nafe tiitana azabaniya
(angelo aku Moto ).
19. Ayi ndithu, usamumvere
(Pa zimene akukuletsazo); Koma
gwetsa nkhope yako, Pansi ndipo
dziyandikitse Kwa Mbuye wako.
&\ 9 Z2i' * 99\' \*\~ v\a&
2) ^^bu^Jj Aj&2>y*y6
<3>
M'sura imeneyi muli kunenedwa za ulemerero wa Qur'an ndi
za ulemerero wa usiku womwe mkati mwake idavumbulutsidwa.
Ndikuti usiku umenewo ngwabwino kuposa miyezi chikwi
chimodzi. Ndikutinso angelo ndi Jiburil amatsika mu usikuwo
potsatira lamulo la Mbuye wawo pa chinthu chilichonse. Ndipo
usikuwo umakhala wa mtendere wokhawokha popanda chovuta
kapena choipa, mpaka kutuluka kwa m'bandakucha.
Surat Al-QadrXCVII
&m&
m
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Ndithu taivumbulutsa
(Qur'an) Mu usiku wa Laila - tul -
Qadr (Usiku wolemekezeka). 1
oA*><**2L<i>W-
-z*
^\M/&i
1 Qur'an mwachidziwikire idali kuvumbulutsidwa pang'onopang'ono kuchokera
ku thambo loyamba (Baitul Izza). Choncho, usiku umene idatsika kuchokera ku
thambo la seveni (Lauh Mahafudwi) kupita ku thambo loyamba udali usiku
wotchedwa Laila - tul - Qadr (usiku wolemekezeka kwambiri) ndipo ndi chifukwa
kukunenedwa kuti Qur'an idatsitsidwa mu usiku wa LAILA-TUL-QADR.
Umenewu ndi usiku umodzi mkati mwa mwezi wa RAMADHANI omwe uli
wodalitsidwa kuposa miyezi chikwi chimodzi. Tanthauzo lake apa ndikuti munthu
ngati achita ntchito zabwino mu usiku umenewu amapeza malipiro monga a
yemwe wachita ntchito zabwino kokwanira miyezi chikwi chimodzi. Ndiponso
amene achita zoipa mu usiku umenewu amapeza machimo onga yemwe
wachita zoipa kokwanira miyezi chikwi chimodzi. Koma Mulungu adaubisa
Surat 97. Al-Qadr Juzu 30 1380
*>•
*V jJUtfl Sjj~*
2. Ndi chiyani chingakudziwitse
za Usiku wolemekezekawu?
3. Usiku olemekezekawu uli
wabwino kuposa Miyezi 1000
(yomwe Mulibe Laila - tul - Qadr).
4. Amatsika Angelo ndi Jiburil
Mmenemo potsatira lamulo la
Mbuye wawo Mulungu
kudzalongosola chinthu Chilichonse.
5. Mtendere!... usiku umenewo,
(Palibe mavuto ndi zoipa) mpaka
M'bandakucha. 1
©j^r^^fs
&Jfc ^ y $iKhy& I ^jjj
fe^l^jy^
^URATAL-BAYYINAH XCVIII^^Sii
___ ^__^_ ^ ^^^ ^a^Mj
„S^:
Anthu a mabuku adadziwa kupyolera mmabuku mwawo
mbiri za Mneneri yemwe adzadze kumalekezero a nthawi,
yemwe ndi Muhammad (SAW). Ndipo nawo Amushirikina a
m'Madina adadziwa za zimenezi kupyolera mwa eni mabuku
aja. Choncho chifukwa cha kudziwa kumeneku padafunika
kumkhulupirira Mneneriyo, akaperekedwa. Koma pamene
Mneneri wa Mulungu Muhammad (SAW) adaperekedwa kwa
iwo pamodzi ndi buku la Qur'an, adatsutsana ndipo adaswa
lonjezo lawo. Choncho zotsatira za kuswa lonjezo lawolo, eni
mabuku, ndi zoipitsitsa kuposa Amushirikina. Onsewa
adzakhala ku moto muyaya tsiku lomaliza. Koma Asilamu, eni
usiku umenewu. Sukudziwika kuti uli pa deti lanji ncholinga choti anthu
alimbike kuchita mapemphero mwezi wonse wa RAMADHANI; koma
ukuyembekezedwa kuti uli mu masiku khumi omaliza, makamaka usiku
woukira pa 21, 23, 25, 27 ndi 29 Kwa yemwe akufuna kupeza madalitso a
usiku umenewu alimbike kuchita mapemphero kwambiri mwezi wonse. Ndipo
apa sikuti usikuwo umakhala ndi chizindikiro cha mtundu wina uliwonse
kusiyana ndi usiku wina, iyayi
1 Adanena BAIDHAWY kuti tanthauzo la aya iyi ndikuti mu usiku umenewu
Mulungu amalamula kuti kukhale mtendere wokhawokha. Koma muusiku wina
amalamula kuti kukhale mtendere ndi masoka.
Surat 98. Al-Bayyinah Juzu 30 1381
*>'
^A 4~Jl OjJ-*
ulemelero, ndiwo zolengedwa zabwino. Malipiro awo
ndikukhala muyaya ku Jannah, ku munda wa mtendere,
ndikukondweretsedwa ndi zimene adzazipeze; zomwe adali
kuzifuna. Malipiro awo adzawapeza amene adali kuopa Mbuye
wake.
Sural Al-Bayyinah XCVIII
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Amene adakanira (Mulungu
ndi Mthenga Wake) mwa omwe
Adapatsidwa Buku ndi
Amushirikina Sadali olekana (ndi
umbuli wawo Ndikusalabadira
kwawo choona) Mpaka pom we
chidawadzera chisonyezo
Choonekera poyera, 1
#- mw?
o^l^jll^W-
-^
"Akafiri" omwe adapatsidwa buku, ndi Ayuda ndi Akhristu. "Amushirikina" ndi
omwe adali kupembedza mafano. Tanthauzo la ma aya awa 1- 4 ndikuti
asadatulukire Muhammad (SAW), Ayuda ndi Akhristu omwe adali ku Madina,
pamene adali kuwauza Amushirikina kuti, "Yayandikira nthawi yotulukira
Mneneri. Ife tidzamtsatira, tidzakhala pamodzi ndi iye. Tidzakumenyani
nkhondo mpaka kukugonjetsani." Adali kuyembekezera kuti Mneneriyo
adzakhala mwa iwo. Pamene adali kumva izi, opembedza mafano aja, adali
odandaula. Iwonso adali kuyembekezera Mneneriyo; limeneli ndilo tanthauzo
la mawu aja oti: "Sadali olekana mpaka pomwe chidawadzera chisonyezo
choonekera poyera".
Apa ndiye kuti fuko lililonse mwa mafuko atatu aja lidali ndi mtima wopitiriza
zipembedzo zawo, osaleka mpaka chiwafikire chisonyezo. Tanthauzo la
"chisonyezo," apa ndi Muhammad (SAW) monga aya yachiwiri yafotokozera.
Pamene adafika Mneneri, opembedza mafano aja ndiwo adayamba
kumukhulupirira, koma Ayuda ndi Akhristu pamene adaona kuti Mneneri sali
wochokera mwa iwo monga m'mene adali kuyembekezera adakhumudwa;
ena mwa iwo adamkhulupirira pomwe ena sadamkhulupirire. Hi ndilo
tanthauzo lakuti, "sadalekane omwe adapatsidwa mabuku mpaka pomwe
chidawafikira chisonyezo."
Surat 98. Al-Bayyinah Juzu 30
1382
*>'
<\A
I 0jJ~>
2. (Yemwe ndi) Mneneri
wochokera Kwa Mulungu
akuwawerengera Makalata
oyeretsedwa (ku zonama). 1
3. Omwe mkati mwake muli
malamulo Oongoka (ofotokoza za
choona). 2
4. Sadalekane omwe
adapatsidwa Mabuku mpaka
pomwe chidawafikira Chisonyezo
(chosonyeza kuti Muhammad
(SAW) ndi mthenga wa Mulungu
Yemwe adalonjezedwa mmabuku
awo).
5. Sadalamulidwe (china) koma
kuti Ampembedze Mulungu
(mmodzi yekha) Ndikuyeretsa
chipembedzo Chake Popendekera
ku choona (ndi kusiya njira Zonama)
ndi kuti asunge Swala ndiponso
Apereke chopereka (cha pachuma
chawo); chimenecho (Ndicho)
chipembedzo choongoka. 3
6. Ndithu, amene
sadakhulupirire (Mneneri) (SAW)
Pakati pa anthu a mabuku ndi
1 Tanthauzo la "Makalata oyeretsedwa kuzonama" ndi Qur'an.
2 Kapena kuti "mkati mwake muli mabuku olingana," ndiye kuti m'Qur'an muli
zophunzitsa za mabuku onse omwe Mulungu adavumbulutsa kwa Aneneri
onse akale.
3 Tanthauzo lake ndikuti "Mneneri uyu" sadadze ndi chinthu cha chilendo
chakuti ndikumukanira. Koma iye akulamula za kupembedza Mulungu
Mmodzi ndi kumuyeretsera chipembedzo Chake; kuima ndi kupemphera,
kupereka chopereka etc. Zoterezi ndizonso adali kuphunzitsa aneneri onse
omwe adadza ndi zipembedzo zoongoka.
Surat 99. Az-Zalzalah Juzu 30
1383 r*ij±\
^ * aijjjji Sj^
opembedza Mafano
adzalowetsedwa ku Jahannama
Ndikukhala m'menemo muyaya;
iwowo ndiwo Zolengedwa zoipa.
7. Ndithu, amene akhulupirira
(mwa Mulungu ndi Mthenga
Wake) ndikumachita zabwino, Iwo
ndiwo zolengedwa zabwino.
8. Malipiro awo kwa Mbuye
wawo, Ndi minda yamuyaya
momwe Ikuyenda pansi pake
mitsinje; adzakhala M'menemo
muyaya. Mulungu adzalandira
ntchito Zawo nawonso adzayamika
zabwino Zake ndi
Kukondweretsedwa nazo (zomwe
adzawapatse); Zimenezo ndi za
yemwe awope Mbuye wake
(Mulungu).
^ijjsjKajj
Ma aya a surayi akulongosola za tsiku lomaliza monga
kugwedezeka kwa nthaka, kutuluka akufa ndi zomwe zidali
mkati mwanthaka, kudabwa munthu ndi kudzifunsa yekha
modzidzimuka, ndi anthu kuchoka mmanda mwawo kuti
akalandire mphoto zawo.
Surat Az-Zalzalah XCIX
\mm
^Xi&jMc V
:£_
g3JR5«.S|
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Likadzagwedezedwa dziko
Q^lt^l^U
-^
®W;J>«j#i
Surat 99. Az-Zalzalah Juzu 30
1384
*j*
S ^ iJjljJl 5j^
Lapansi kugwedezeka kwake
Kwamphamvu
2. Ndipo nthaka idzatulutsa
mitolo Yake (zinthu zomwe zidali
mkati Mwake, monga akufa ndi
miyala Yamtengo wapatali),
3. Ndipo munthu adzanena
(mwa mantha, Ndikudabwa nthawi
imeneyo) Ha! Yatani nthaka,(kodi
Kiyama yafika)?
4. Tsiku limenelo idzanena
nkhani Zake zonse, (zabwino
kapenaZoipa). 1
5. Pakuti Mbuye wako
adzailamula Kutero (kuti
igwedezeke ndikunena Zimene
zinkachitika pamwamba pake).
6. Tsiku limenelo anthu
adzachoka (M'manda) ali
mmagulu obalalika kuti
Akasonyezedwe ntchito zawo
(ndikudziwa Chiwerengero chawo
chimene Chili kwa Mulungu).
1 Idzanena nthaka pa tsiku limenelo pamene Mulungu adzaiuza kuti inene
monga momwe amazinenetsera zinthu zimene chikhalire sizilankhula, pakuti
Mulungu ndi wamphamvu zonse.
Kapena m'mene iti idzakhalire nthaka kudzakwanira munthu kudziwa kuti
ikutanthauza chakuti, popanda kutulutsa mawu monga momwe timadziwira
munthu wosangalala ndi chisoni; wanjala ndi wokhuta popanda
kulankhula. Nkhani zomwe idzafotokoza nthaka pa tsiku limenelo, monga
momwe adanenera Mneneri Muhammad (SAW), ndi izi>
Tsiku la chiweruzo nthaka idzamuikira umboni munthu aliyense kapena
m'badwo uliwonse pa chimene adachita pamwamba pake (pamwamba pa
nthaka). Limeneli ndilo tanthauzo la mawu aja oti " Nthaka idzanena nkhani
zake."
© UjU»J e>^si v^4jj.
Surat 100. A1-' Adiyat Juzu 30 1385 r * ^jA-i 1 • * obMaJi 5^
7. Choncho, amene angachite
chabwino Cholemera ngati kanjere
Kakang'ono, adzaona malipiro
ake. 1
8. Ndipo amene angachite
choipa Cholemera ngati kanjere
Kakang'ono, adzaona malipiro
ake. (Mulungu sachitira chinyengo
aliyense).
SURAT AL-'ADIYAT C
n^_ ^m
Kumayambiriro a surayi Mulungu wolemekezeka walumbirira
akavalo omenya nkhondo kuti ndithu, munthu ali wokanira
kwambiri pamtendere wa Mbuye wake, (Mulungu). Ndithu, iye
mwini adzaikira umboni pazimenezi tsiku lomaliza, ndikuti iye
pokonda chuma ali wa msulizo. Ndipo kotsirizira kwake
yafotokoza za kuuka ndi kuweruzidwa pa tsiku lomaliza.
Surat Al-' Adiyat C
— -"~"
m mm&t
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Ndikulumbirira akavalo
Othamanga ali ndi phuma,
2. Ndiotulutsa moto kuzikhotwa
(Pomenyetsa miyendo m'miyala),
3. Ndiothira nkhondo adani
Mmawa (dzuwa lisadatuluke);
0&£\<£®\&\j
^
1 (Ndime 7-8) Ma aya awiriwa akutidziwitsa kuti munthu adzalipidwa pa
chilichonse chimene akuchita, chabwino kapena choipa, ngakhale chikhale
chochepa monga kulemera kwa kanjere kochepa kwambiri.
Surat 100. Al- 4 Adiyat Juzu 30 1386 1" . *>! > • • olouJi 5^
4. Ndikuulutsa fumbi lambiri
(Kwa adani) nthawi imeneyo,
5. Ndikulowerera mkatikati
mwa Adani.
6. Ndithu, munthu ali wokanira
Mbuye wake, (Sathokoza Mulungu
pazimene Amdalitsa nazo). 1
7. Ndithudi iye pazimenezi ndi
Mboni (yozichitira yekha
Kupyolera mzochitachita zake).
8. Ndipo ali wokonda chuma
Kwambiri (ndiponso
ngwamsulizo).
9. Kodi sakudziwa
zikadzatulutsidwa Za m'manda;
10. Ndikudzasonkhanitsidwa
Ndikudzaonekera poyera zomwe
Zidali m'mitima?
11. Ndithu tsiku limenelo
Mbuye wawo Adzawadziwa
kwambiri (Ndikuwalongosolera
zonse zochita zawo).
<3S$<3^MS&
uCud^^il Sr^vlj
1 Tanthauzo la "kukanira Mbuye wake" ndi kuukanira mtendere Wake. Ndipo
kukanira mtendere ndiko kusagwiritsira ntchito mtenderewo mnjira zabwino,
monga m'mapemphero ndi zina zotero.
2 Kapena kuti ali wofunitsitsa chuma kwambiri; kumeneko ndikumangoti
mtima dyokodyoko pachuma. Ukachipeza ndikumachichitira umbombo ndipo
ndikumaganiza kuti chumacho nchopambana china chilichonse.
3 "Kuwadziwa kwambiri," kukutanthauza kuti lye ngodziwa zazikuluzikulu ndi
zazing'onozing'ono zoonekera poyera ndi zobisika. Tsiku limenelo
adzawalipira chilichonse chimene adachita.
Surat 101. AI-Qari'ah Juzu 30 1387 f * *>i 1*1 apjUil 5^
Surayi yayamba ndikuopseza kwa kugunda kwamphamvu
komwe kudzagonthetsa makutu a anthu pa tsiku la kutha
kwadziko. Ndipo yalongosola machitidwe ena a tsiku limenelo a
anthu ndi mapiri. Ndiponso yalongosola za amene zabwino zawo
zidzalemera pa sikelo ndikupepuka zoipa zawo.
Sural Al-QarVah CI
l mm
&m\K?A
,*:
t'%\
o£*3\^3\&\j
-*£
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Kugunda kwa phokoso (la
Kiyama)!
2. Kodi kugunda kwa
phokosolo Ndi chiyani?
3. Ndichiyani
chingadzakudziwitse za Kugunda
kwa phokoso (la Kiyama Komwe
kudzawakomole anthu)?
4. Limenelo ndi tsiku limene
anthu Adzakhala ngati agulugufe
Obalalika,
5. Ndipo mapiri adzakhala ngati
Ubweya opakidwa penti,
womwazidwa (Wongouluka uku
ndi uku mumlengalenga).
1 Apa, pakutanthauza kuti anthu adzakhala ali balalabalala ngati agulugufe
ndipo azidzangodziponya uku ndi uku, osadziwa kopita. Imeneyo ndi nthawi
yotuluka m'manda.
Surat 101. Al-Qari'ah Juzu 30 1388 ? * *>» \0 *pjUJi ojj-
6. Tsono amene muyeso wake
(wa zinthu Zabwino) udzalemere
(ndikupepuka Zoipa). 1
7. Ndiye kuti iye adzakhala mu
umoyo Wosangalatsa (patsiku
lachiweruzo).
8. Ndipo yemwe muyeso wake
(wa zinthu Zabwino) udzapepuka
(ndi kulemera Zoipa),
9. Ndiye kuti mbuto yake ndi ku
Hawiya.
10. Kodi ndi chiyani
chingakudziwitse Za Hawiya?
11. Umenewo ndi mo to woyaka
mwaukali!
via ■* immtm lu,u
^.^■wtffc
kk£&
l SURAT AT-TAKATHUR CII
Surayi ikudzudzula aliyense wosiya malamulo a Mulungu
chifukwa chotanganidwa ndi zamdziko. Ndipo yawachenjeza kuti
adzadziwa zotsatira za kunyozera kwawo malamulo a Mulungu
pamene adzauona moto masomphenya ndikufunsidwa za
mtendere uliwonse umene Mulungu adawadalitsa nawo kuti
adauchitira chiyani.
1 Tsiku limenelo ntchito zonse zabwino ndi zoipa zidzayesedwa ndi muyeso
wa Mulungu, koma sitidadziwitsidwe kuti muyeso umenewo udzakhala wotani
udzayesa zonse zazikulu ndi zazing'ono zomwe mpaka za mumtima.
Surat 102. At-Takathur Juzu 30
1389 r. *>» i.ryiUiSjj-,
Surat At-Takathur CII
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Kwakutangwanitsani
kusonkhanitsa Chuma chambiri
ndi wana. 1
2. Mpakana mwapita kumanda
(Mwamwalira ndikukalowa
Mmanda).
3. Sichoncho! mudziwa
posachedwapa. 2
4. Ndiponso sichoncho!
Mudziwa Posachedwapa.
5. Sichoncho! mukadakhala
mukudziwa, Kudziwa
kwachitsimikizo (sibwenzi
Mukutangwanika ndi zamdziko).
6. Ndithudi mudzauona moto,
7. Kenako mudzauona ndithu
ndi diso la Chitsimikizo.
8. Tsono patsikulo ndithudi
mudzafunsidwa 3
4'i
1
O&rgS^&J
-&
&5^il'-
®u^^y^<I>!
1 (Ndime 1-2) Ndi chizolowezi cha anthu kupikisana pa chuma ndi pa ana.
Choncho, mma aya awa: 1-2 Mulungu akuwauza: Kupikisana kwawo
kochuluka, kukonda za m'dziko kwambiri, kwaiwalitsa kutumikira Mulungu
mpaka imfa kuwapeza.
2 Tanthauzo lake ndilakuti, pamene idzakufikirani imfa mudzadziwa kuti
mudali kutaya nthawi ndi zinthu zopanda pake.
3 Munthu aliyense ndi chilichonse chimene ali nacho ndi mphatso yochokera
kwa Mulungu. Choncho, pa tsiku lomaliza adzafunsidwa za momwe
adagwiritsira ntchito mphatso zimenezi, kaya m'njira yoipa kapena yabwino.
Surat 103. Al-'Asr Juzu 30
1390
*>'
S • T j~f*"b\ *JJ**
Mulungu Wolemekezeka akulumbirira nthawi msurayi
chifukwa chakuti nthawi yasonkhanitsa zodabwitsa zambiri mkati
mwake, zomwe ndi maphunziro kwa anthu olingalira, zomwenso
zikusonyeza mphamvu za Mulungu ndi luso lake pa chilichonse,
kamba ka nthawi , munthu salekana ndi kuchepekedwa ndi
kusintha m' ntchito zake ndi makhalidwe ake, kupatula
okhulupirira amene amachita zabwino ndikumalangizana pakati
pawo kugwiritsa choona cha Mulungu, ndikulangizana za kupirira
pazimene alamulidwa kuzitsata ndi kupewa zomwe aletsedwa
kuchita.
Surat Al-'Asr CHI
m^smm'JM
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Ndikuilumbirira nthawi. 1
2. Ndithu, munthu aliyense ndi
Wotaika (chifukwa
chakugonjetsedwa Ndi zilakolako
zake),
3. Kupatula amene akhulupirira
(mwa Mulungu) ndi kumachita
zabwino, Ndikumalangizana
kutsatira choona Ndiponso ndi
kumalangizana za Kupirira
(potsatira malamulo A Mulungu
QWH^*
-^
Chinthu cha mtengo wapatali kwa munthu padziko lino ndi moyo wake.
Choncho mphindi iliyonse imene akuigwiritsa ntchito pa zinthu zabwino ndiyo
imene idzamuthandiza. Ndipo mphindi iliyonse imene akuigwiritsa ntchito mu
zinthu zoipa kapena zopanda pake, kumeneko ndiko kutaika kwake; (kuluza).
Surat 104. AI-Humazah Juzu 30
1391 r. *>i
^ « £ 3j*Al Ojj— i
ndi zina zovuta za mdziko).
JESp^™"""""^'""""" ' """""
[T SURAT AL-HUMAZAH CIV
M'surayi muli lonjezo la chilango choopsa kwa munthu amene
ali ndi chizolowezi chojeda ndi kunyoza anthu, powalozera ndi
maso kapena kulankhula. Ndiponso amene amati akasonkhanitsa
chuma amachiwerengera pafupipafupi mokhumbiza ena uku
akuganizira kuti chumacho chimkhazika muyaya.
Surat Al-Humazah CIV
# mm
_____
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Kuonongeka koopsa
kudzampeza Aliyense wojeda ndi
wonyoza Anthu polozera (ndi maso
kapena Kuyankhula ndi lirime), 2
oj&3\^3\&\j
-+±
Mgulu la otaika mwapatulidwa anthu olungama amene zochita zawo zili
zolungama, omwe amalamulira kutsatira njira yolungama ndi kupirira. Anthu
otere saataika, chifukwa chakuti nthawi yawo amaigwiritsira ntchito pa zinthu
zabwino, zowathandiza padziko ndi pambuyo pa imfa.
Kupirira kulipo mitundu inayi:-
(a) Kupirira pochita zinthu zabwino zomwe zili zovuta kwa munthu kuzipitiriza,
monga kupemphera swala zisanu.
(b) Kupirira posiya kuchita zoipa zimene zili zovuta kwa munthu kuti azileke.
(c) Kuwapirira anthu anzako; kupirira ndi zoipa zawo posawabwezera choipa
chilichonse.
(d) Kupirira ndi mazunzo a padziko, monga njala, matenda, kusauka ndi zina
zotero.
2 Kujeda kwa mtundu uliwonse ndi koipa. Anthu ambiri amaganiza kuti kujeda
ndi chinthu chochepa, saona kuti ndi chinthu choipa, pomwe Qur'an ikuletsa
kwatunthu mpaka mwakuti imamufanizira munthu wojeda ngati munthu
yemwe amadya minofu ya mnzake wakufa. Mu aya imeneyi, Mulungu wanena
kuti "Wayilun" lomwe tanthauzo lake ndi "Kuonongeka koopsa." Choncho
nkofunika kwa munthu aliyense kupewa khalidwe lojeda.
Surat 104. AI-Humazah Juzu 30
1392
*>'
y • t Sj^ii 3jj^
2. Yemwe wasonkhanitsa
chuma Ndikumachiwerengera. 1
3. Akuganiza kuti chuma
chakecho Chimkhazika (padziko)
muyaya (Ndikumteteza kuzimene
sakuzifuna).
4. Sichoncho! (asiye maganizo
amenewo) Ndithudi, akaponyedwa
ku Moto woononga (chifukwa cha
kuipa Kwa zochita zake).
5. Ndi chiyani
chingakudziwitse Za moto
woonongawu?
6. Umenewu ndi moto wa
Mulungu woyaka (Nthawi zonse,
woononga chilichonse
Choponyedwa mmenemo);
7. Umene umakwera mpaka ku
mtima. 2
8. Ndithu, motowo ukawazinga
(ndi Kuwatsekera makomo);
9. Munsanamira za zitalizitali
(Kotero kuti sakatha kugwedezeka
Mmenemo kapena kupulumuka).
ft£&\$&S®$
®k&&&iffi>
©*JsjtfUfc!$
Mmenemo ndi momwe alili munthu wa umbombo, kukoma kwa chuma kwa
iye, ndikuchisonkhanitsa ndikumachiwerengera akakhala ndi danga; sikuti
akufuna kudziwa kuchuluka kwake koma kungokondweretsedwa
ndikuchiwerengako. Saganizira zimene zingamuthandize iye mwini kapena
kuthandiza anzake.
Chuma ntchito yake ndikuti chimthandize mwini chumacho pa zinthu zabwino
zosiyanasiyana pamodzi ndi anzake, osati kungochikhazika
ndikumangochiwerengera mokhumbiza ena.
2 Moto umenewu, sukapsereza kunja kokha, ukapsereza mpaka ndi mumtima
momwe.
Surat 105. Al-Fil
Juzu 30
1393
r* *>»
\ * O J-jlJl 5jj~*
SURAT AL-FIL CV
— -,-
Mulungu akulongosolera Mtumiki Wake nkhani ya eni njovu
amene adafuna kugumula nyumba ya Mulungu. Ndipo
akumsonyeza phunziro limene lili m'nkhaniyi lomwe likusonyeza
ukulu wa mphamvu za Mulungu kudzanso chilango Chake kwa
amene akunyoza zinthu Zake zopatulika.
Ndithu, Mulungu adawatumizira magulu ankhondo amene
adawaonongeratu kwatunthu kotero kuti matupi awo adakhala
ngati udzu wodyedwa ndi nyama kapena gaga wambewu
zoonongedwa ndi tizilombo.
Surat Al-Fil CV
; $M$ M
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Kodi sudaone momwe
Mbuye wako Adawachitira eni
njovu? 1
(W^9i^
~w
&$U^eg55 <3&$
1 Sura imeneyi ikufotokoza mbiri imene idachitika pafupi ndi mzinda wa Makka
mchaka cha 570 A.C. Dziko la Yemen lidali kulamulidwa ndi anthu a mtundu
wa Ahabashi (ochokera ku Ethiopia). Iwowo pa nthawi imemeyo adali
Akhristu. Bwana Mkubwa (Gavanala) waku Yemen pa nthawiyo adali Abraha.
Abrahayu adafuna kuwaletsa Arabu kuti asamapite ku Makka kukayendera
Kaaba. Pa chifukwa ichi adamanga tchalichi lalikulu kwambiri ndiponso
lokongola lomwe lidali mu mzinda wa Sanaa. Adawakakamiza Arabu
kuyendera tchalichilo m'malo mopita ku Al-Kaaba Pamene Arabu adamva
zimenezi zidawanyansa. Ndipo adadza munthu wina wochokera ku fuko la
Kanaani ndikukalowa m'tchalichimo ndikuchitiramo chimbudzi. Adatenga
chimbudzicho ndikupakapaka m'zipupa za tchalichi lija chifukwa
chonyansidwa ndi nyumbayo kuti siidali yoyenera kulowa m'malo mwa Kaaba.
Pamene adaona izi, Abraha adakwiya kwambiri ndipo adalumbira kuti
sachitira mwina koma kukagumula Kaaba. Adasonkhanitsa gulu la nkhondo
lalikulu momwe mudalinso njovu zakuti zikamthandize kugumula Al-Kaaba.
Choncho adauyatsa ulendo kupita ku mzinda wa Makka.
Abraha pamene adafika ku Makka, adatumiza munthu kwa Arabu kuti
Surat 105. AI-Ftl Juzu 30 1394 r * *>i
\ ♦ O J-ji3l Ojj-j
2. Kodi sadachichite chiwembu
Chawo kukhala chosokera
(Chopanda phindu?)
3. Adawatumizira
magulumagulu a Mbalame
otsatizana. (ndipo Adawazungulira
mbali zonse;)
4. Zimawagenda ndi miyala ya
moto;
5. Adawachita ngati m'mera
wodyedwa (ndi Nyama ndi
kulavulidwa).
s^a;*^'-'' 1
0^JjT!^>^ J^Ij
<i \^&jfJ^ > HA?
®djtfLx&^&>6
awafotokozere kuti iye sadadze kudzawathira nkhondo, koma adadzera
kudzagumula Al-Kaaba. Choncho adawapempha kuti amupatse danga kuti
atero. Abdul Mutwalib adalamula anthu ake onse kuti achoke mu mzindawo
apite ku mapiri.lye adakalowa Mnyumba ya Kaaba ndipo adapempha
Mulungu kuti ayipulumutse nyumba Yake yopatulika. Kenaka nayenso
adawatsatira anzake ku mapiri kuja ndipo adangokhala phee, kuti amuone
bwino yemwe adali kulimbana ndi Mulungu pomugumulira nyumba Yake.
Abraha pamene adadziwa kuti Arabu atuluka mu mzindamo adakonzeka
kulowa m'Makka ndi kugumula AL-Kaaba. Koma Mulungu Wamphamvu
zonse adamutumizira gulu Lake la nkhondo monga momwe mukuwerengera
pa aya yachitatu. Ankhondo a Abraha ena adafera pompo koma ena
pamodzi ndi iye mwini, adathawa ndikukafera kwawo ku Yemen. Pa chifukwa
chimenechi Arabu ankachitcha chaka chimenechi kuti "chaka cha njovu."
Choncho mwana aliyense wobadwa m'chakachi ankatchedwa mwana
wobadwira m'chaka cha njovu. Ndipo Mneneri Muhammad (SAW) adabadwa
m'chaka chimenechi ndipo ankadziwikanso monga mwana wobadwa m'chaka
cha njovu.
Surat 106. Quraish Juzu 30
1395
*>'
> • 1 J* J °Jf
M'surayi Mulungu akufotokoza za mtendere Wake umene
udali pa Aquraish powadalitsa ndi nyumba Yake yopatulika
imene adali kuiteteza kwa adani Ake. Adawakhazika mmbali
mwake ndipo adapeza ulemerero ndi mtendere.
Amayenda nthawi ya chirimwe kupita ku Sham ndipo nthawi
ya dzinja amapita ku Yemen ndikumakachita malonda
mwamtendere popanda chowapinga chilichonse, pomwe anzawo
adali kufwambidwa.
Chimenechi ndi chisomo chofunika kuchiyamika, ndi
kumpembedza amene adawachotsera njala ndi mantha.
Surat Quraish CVI
,n m »
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Cholinga chakuwachita
MaQuraish Kuti apitirize
chizolowezi chawo, 1
Q^^t^jM«&U-
©,
\&^m
(Ndime 1-4) Al-Kaaba, ndidzachidziwikire kuti, adali malo opatulika kwa
Arabu onse kuyambira nyengo ya Ibrahim (Abraham) (AS) yemwe adamanga
nyumbayi potsatira lamulo la Mulungu. Aquraish amene ankasunga ndi
kuyang'anira nyumba yopatulikayi, adali kupatsidwa ulemu ndi Arabu ena
onse. Ndipo pa chifukwa chimenechi adali kutha kuyenda ulendo wopita ku
Yemen nthawi ya dzinja, ndiponso ku Sham nthawi yachirimwe kukachita
malonda ndikubwerera bwinobwino. Sadali kuputidwa ndi achifwamba m'njira,
pophedwa kapena kulandidwa chuma chawo momwe ankachitiridwa Arabu
ena.
Pamene idamveka nkhani ya njovu.kulemekezedwa kwawo kudaonjezeka
kuchokera kwa mitundu yonse ya Arabu. Mu sura imeneyi, Mulungu
akuwakumbutsa za madalitso amenewa ndiponso akuwauza kuti
adawafewetsera kayendedwe ka maulendo awo nthawi ya dzinja ndi chilimwe
kuti akachite malonda ndikupeza chakudya ndi zina zofunika pa moyo wawo.
Adawapatsa chitetezo posakhala ndi mantha m'njira; mantha omwe mitundu
Surat 106. Quraish Juzu 30 1396 ? * *>'
> * t J*lJ 5 JJ-"
2. Apitilize chizolowezi chawo
choyenda Nthawi ya dzinja
(kunka ku Yemen) Ndi nthawi
yachirimwe(kunka Ku Sham
kukachita malonda,
Mosatekeseka ndi mopanda
mantha).
3. Choncho, amupembedze
Mbuye wa Nyumba iyi (Al-Kaaba
amene Adachititsa kuti athe
kuyenda Maulendo awiriwo);
4. Yemwe amawadyetsa
(nthawi imene Arabu anzawo) ali
m'njala, Amawapatsa chitetezo
(pomwe Anzawo) ali ndi mantha.
h^\fy^M
%Q\^Ci>\jo^
Surayi ikukamba za otsutsa tsiku la malipiro limene lili tsiku
lomaliza. Ndipo yalongosola mbiri zawo motere: lye ndi yemwe
amapondereza ana amasiye ndikuwakalipira mwankhanza, osati
kuwalangiza miyambo yabwino. Iyenso ndi yemwe
samalimbikitsa ena ndi mawu kapena ndi ntchito zake monga
kudyetsa osauka chifukwa iye ndi woumira pazimene alinazo
mmanja. Kenako yatchula gulu lofanana ndi wotsutsa tsiku
lamalipiro. Iwowa ndi amene akuchitira mphwayi mapemphero
awo. Sachita mapemphero awo moyenera, koma akuwachita
ina ya Arabu idali nawo. Madalitso onsewa ankawapeza chifukwa cha
nyumba ya Al-Kaaba. Choncho kudali koyenera kwa iwo kumupembedza
Mwini nyumbayo, osati mafano.
Pakadapanda nyumba Yakeyo sakadatha kumayenda maulendo mwa
chitetezo, ndiponso sibwenzi kukudza aliyense ku mzindawo (Makka)
chifukwa mukadakhala mulibe chodzetsa alendo
Siirat 107. Al-Ma'un Juzu 30 1397 T * *>
> * V O^Plll 9jj*>
monga chithunzi chopanda tanthauzo. Amangoonetsera zochita
zawo kwa anthu. Amamana osowa chithandizo chawo. Ndipo
sura iyi ikuwalonjeza chilango ndikuonongeka kuti asiye
machitidwe awowo.
Surat Al-Ma'un CVII
: i -.
mmmz
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Kodi wamuona yemwe
akutsutsa Za mphoto (ndi
chiwerengero Cha tsiku
lomaliza)? 1
2. lye ndi yemwe akukankha
wamasiye (Mwankhanza).
3. Ndipo salimbikitsa (ena
pamodzi ndi lye mwini) kudyetsa
osauka.
4. Choncho kuonongeka kuli pa
Ena mwa opembedza (amene ali
Ndi mbiri izi):
5. Omwe amachitira mphwayi
mapemphero Awo. 2
oM^^3\^W
&^M&3i
fy$Kc$&i*
%&^¥<P&
wm
^u^s^
Sura imeneyi ikufotokoza m'mene alili makhalidwe awanthu ambiri,
ngakhale amene amadzitcha kuti ndi Asilamu. Aliyense amene ali ndi
makhalidwe otere ndiye kuti sakhulupirira za tsiku la chiweruzo. Akadakhala
kuti akukhulupirira za tsikuli, sibwenzi akusiya kuwachitira za chifundo
osauka ndi amasiye. Sapereka chithandizo ngakhale kulimbikitsa ena ngati
iye alibe.
Kuchitira mphwayi mapemphero (swala), kumeneku ndiko kupemphera uku
maganizo ali kwina, kapena kupemphera modukizadukiza. Tsiku lina
nkupempherapo, tsiku lina ayi. Kapenanso kupemphera modzionetsera kwa
anthu (riyaa).
Surat 107. Al-Ma'un Juzu 30
1398
*>'
) * V dj*&\ 9jj~>
6. Amenenso (akamachita
mapemphero Awo)
amadzionetsera (kwa anthu
Mwachipha maso kuti apeze
ulemerero Ndi kutamandidwa
mmitima mwa anthu); 1
7. Ndipo amamana ziwiya
(zawo posabwereka Anzawo
zinthu zofunika pa moyo wa
Aliyense monga nkhwangwa,
mpeni, Mtondo ndi zina zotere).
&,
>&%&&
s->9K'\i'*9' , >"
t&**#
SURAT AL-KAUTHAR CVIII
^_
M'sura imeneyi Mulungu akutchula ufulu Wake umene
adamchitira Mneneri Wake (SAW) pompatsa zabwino zambiri
ndi chisomo chachikulu pano padziko ndi tsiku lomaliza. Ndipo
wamuuza kuti apitilize kupemphera swala yake ncholinga
chofuna chikondi Chake osati china ayi. Ndiponso akumuuza kuti
aphe nyama ya nsembe imene ili yodalirika mchuma chake
posonyeza kuthokoza pazimene Mulungu wampatsa monga
ulemerero waukulu.
Ndipo sura imeneyi yamaliza ndi nkhani yakudukidwa
mwawi wa mdani wake amene adali kuda Mtumiki (SAW)
kwambiri ndikumamutcha kuti ngopanda mwawi.
Riyaa ndiko kuchita ntchito yabwino ndicholinga choonetsa anthu, kuti
akuone kuti ndiwe wabwino, mwina kuti ukhale wokondedwa ndi anthu.
Kapenanso kuti upeze za m'matumba mwawo. Amenewa ndi machitidwe a
"Shiriki " (Kum'phatikiza Mulungu ndi zolengedwa Zake pa mapemphero)
Ndiponso, ndi njira yobera anthu.
Surat 108. Al-Kauthar Juzu 30 I 1399 I T . s-jA-i \ . A jJj&i t ir >
Surat Al-Kauthar CVIII
.3? — — ^-
. ^r^J^=3- / <^LCLiA \
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Ndithu, takupatsa zabwino
Zambiri (zina mwa izo ndi Mtsinje
wotchedwa Kauthar). 1
2. (Pakuti ndakupatsa
zimenezo), Pitiliza kupembedza
Mbuye wako (Moyera mtima)
ndipo ipha nsembe yako
(Chifukwa chakuthokoza Mulungu
Pazimene wakupatsa, monga
Ulemerero ndikukusankhira
Zabwino zambiri). 2
3. Ndithu, mdani wako Ndiye
ali wopanda mwawi.
Q^Jlfc^J)!^
-a
©^atf'' 1(? <
*&£&&
%#}£&&&
Tanthauzo la "zabwino zambiri" apa, ndi uneneri, maphunziro, ntchito
zabwino, ulemerero, kupambana pakukhala ndi omutsatira ambiri ndi zabwino
zina zam'dziko lino lapansi ndi tsiku lomaliza, zosawerengeka zomwe
sadapatsidwe aliyense pambuyo pa iye ngakhale mtsogolo mwake. Ndithu,
zimenezi, popanda chikaiko, ndizabwino kwambiri kuposa chuma ndi ana.
2 Tanthauzo loti "Mbuye wako yekha umupembedze" kuti amupembedze
Mulungu yekha, asachite chiphamaso, asakhale monga amene amachita
mapemphero ndi cholinga choti adzionetsere kwa anthu. Ndikutinso apereke
nsembe m'dzina Lake, osati azimu ndi zina zotero.
3 Yemwe akukunena iwe kuti ndiwe wodukidwa ndi mwawi, sichoncho, koma
iyeyo ndiye ali wodukidwa ndi mwawi, pakuti iwe takupatsa zabwino zambiri ,
osafanana ndi iye ngakhale kuti iye ali ndi chuma ndi ana.
Adani a Mtumiki (SAW) adali kukondwera kwambiri pamene ankaona kuti ana
ake onse achimuna atha kumwalira, iwo ankaona kuti palibe ubwino uli onse
kwa munthu pano padziko ngati sadapatsidwe ana achimuna ndi chuma. Pa
chifukwa ichi, adali kumutcha "Abutaru," wopanda madalitso. Msura imeneyi
Ambuye Mulungu akumtonthoza Mneneriyo ndiponso akuyankha adani ake.
Surat 109. Al-Kafirun Juzu 30 I 1400 I T • *>» \ * S Ojjdi&i 5jj~-
M'sura imeneyi Mulungu akulamula Mneneri Wake kuti
awauze okanira (osakhulupirira) kuti sipadzapezeka chimvano
pakati pa iye ndi chipembedzo chake choona ndi pakati pa iwo
ndi chipembedzo chawo chabodza. Koma iye adzapitiriza
kupembedza Mulungu amene palibe wina wopembedzedwa
mwachoonadi koma Iye. Ndipo naonso adzapitiriza kupembedza
mafano awo omwe sangathandize chilichonse.
Surat Al-Kafirun CIX
\mmm
fcCi —
':(
^g= , , _JJ
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Nena (iwe Mtumiki) (SAW):
Ee'.InuAnthu osakhulupirira! 1
2. Sindipembedza chimene inu
Mukuchipembedza (kusiya
Mulungu).
3. Inunso simumpembedza
ojk£\<&$\&\jr
h&^K$&$
© <jj&^joU> jJ^l^f
1 (Ndime 1-6) Osakhulupirira a mu mzinda wa Makka pamene adaona kuti
atopa, sangathe kuzimitsa dangalira la Usilamu ndipo adamuona Mneneri
(SAW) tsiku lililonse akuonjezera khama pa ntchito yake, chipembedzo nacho
chikunkerankera mtsogolo, adapempha Muhammad (SAW) kuti pakhale
chimvano pakati pa iwo ndi iye choti amupembedze Mulungu wa Mneneri
(SAW) chaka chimodzi pamodzi naye, nayenso pa chaka chinacho
asanganikirane nawo popembedza milungu yawo chaka chimodzinso.
Kumeneku ndiko kuti chaka, apembedze Mulungu wa Mneneri (SAW),
nayenso apemphere milungu yawo chaka chinacho. Apa ndipo pamene
idavumbulutsidwa surayi. Cholinga chake ndi ichi: Inu muli ndi milungu
yanu, inenso ndili ndi Mulungu wanga. Sizingatheke kusanganikirana pakati
pa milungu yanu yonama ndi Mulungu wanga woona, ngakhalenso ndi
mapemphero anu onama ndi mapemphero anga oona. Inu muli ndi
chipembedzo ndichikhulupiriro chanu, inenso ndili ndi chipembedzo ndi
chikhulupiriro changa.
Surat 109. Al-Kafirun Juzu 30
1401
r * ^jA-i ^ * * o ^i&i 5^^
amene ine Ndikumpembedza
(yemwe ndi Mulungu mmodzi).
4. Ndiponso ine
sindidzapembedza Chimene inu
mwakhala mukuchipembedza
(Chifukwa inu ndinu ophatikiza
Mulungu ndi zinthu zina).
5. Ndipo inu
simudzampembedza Amene ine
ndikumpembedza (Yemwe ndi
Mulungu mmodzi)
6. Inu muli ndi chipembedzo
chanu (Chimene
mkuchikhulupirira), Inenso ndili
ndi chipembedzo Changa (chimene
Mulungu Wandisankhira).
©^sJl^Ij; $J*&\yj
®u^llit^JLi>ol^
&&}'&&&
SURAT AN-NASR CX
Surayi ikumuuza Mtumiki (SAW) kuti chikadza
chipulumutso cha Mulungu ndikugonjetsa Makka, ndikutinso
akaona anthu akulowa mchipembedzo cha Mulungu
mmagulumagulu, pamenepo amulemekeze Mulungu ndi
kumyamika ndi kumyeretsa kuzinthu zosayenera kwa lye.
Ndikutinso ampemphe chikhululuko kuti chimfikire iye ndi
anthu ake okhulupirira. Chifukwa chakuti Mulungu
ndiwolandira kulapa kwa anthu ake ndikuwakhululukira
zolakwa zawo.
Surat 110. An-Nasr Juzu 30 1402 T * *>» ) ) * j-aJ» $;>-»
SuratAn-NasrCX
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Chikafika chipulumutso cha
Mulungu Ndi kugonjetsa (mzinda
wa Makka Kwa iwe ndi
okutsatira), 1
2. Ndi kuwaona anthu akulowa
M'chipembedzo cha Mulungu ali
Magulumagulu,
3. Pamenepo lemekeza Mbuye
wako ndi Kumtamanda ndiponso
mpemphe Chikhululuko, ndipo lye
ndiwolandira Mochuluka kulapa
(kwa anthu Ake). 3
l%& W*$& '7:^
o&&\<&$\&W
*-%^j^>\
Hi ndi lonjedzo la Mulungu kwa Mneneri wake (Muhammad) (SAW) kuti
amthandiza kumpulumutsa kwa adani ake amene adali kumuzunza ndi
kufuna kumupha. Lonjezoli lidali lakuti iye adzaulamulira mzinda wa adaniwo
momwe adamutulutsa.
2 Mneneri (SAW) pamene adalowa mu Mzinda wa Makka ndi kugonjetsa
adani ake monga momwe Mulungu adamulonjezera, a kafiri adali kubwera
m'mafukomafuko kudzalowa m'chipembedzo cha Chisilamu.
3 Tanthauzo la kuuzidwa Mneneri Muhammad (SAW) kuti zikachitika zimene
adalonjezedwa, amulemekeze Mbuye wake, amupemphe chikhululuko,
chikhalirecho iye adali kuchita zimenezo, izi zimatanthauza kuti moyo wake
wayandikira kutha, watsala pang'ono kumwalira. Choncho adalamulidwa
kuonjezera mapemphero kuti aonjezere kulinganiza tsiku lake lomaliza.
Imeneyi ndi imodzi mwa Surah zimene zidavumbulutsidwa kotsirizira kwa
moyo wa Mtumiki (SAW). Pamene idavumbulutsidwa Surayi, ena mwa
maswahaba (omutsatira) adazindikira chinsinsi cha Surayi; adali kulira poona
kuti Mneneri (SAW) amwalira posachedwa. Pambuyo povumbulutsidwa
Surayi, Mneneri (SAW) sadakhalenso ndi moyo wautali.
Surat 111. Al-Masad Juzu 30 I 1403 I T • *>i U 1 jUL» Sj^
Surayi ikulongosola za kuonongeka kwa Abu Lahabi yemwe
adali mdani wa Mulungu ndi Mneneri Wake. Ndikuti
pakuonongekako chuma chake kudzanso ulemerero wake
sizidamthandize. Ndipo yamulonjeza kuti tsiku lomaliza
adzalowa kumoto woyaka mwamphamvu ndikuotchedwa
mmenemo. Ndiponso yamphatikiza iye ndi mkazi wake
pachilangocho. Makamaka mkazi wake adzakhala ndi chilango
chakechake chomangidwa chingwe mkhosi mwake
ndikumakokedwa kumoto; kumlanga pachifukwa cha zimene
adali kumchitira Mneneri wa Mulungu ndi kuipitsa uthenga wake.
Surat Al-Masad CXI
mm
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Aonongeka manja a Abi
Lahab (Omwe adali kuwagwiritsa
Ntchito pozunza Asilamu).
Nayenso wawonongeka. 1
2. Chuma chake ndi ulemerero
wake (Umene adaupeza)
o^l^jM^
■-ufl
-r'rf *"
&<#!
UuC^O
®CCZ\1aj ^3U^-(/^lU
1 (Ndime 1-4) Pa chiyambi cha uneneri wa Muhammad (SAW) adalamulidwa
kuti aulalikire uthenga wabwinowo kwa abale ake apafupi; adawasonkhanitsa
ndipo adawalalikira ndi kuwachenjeza za chilango cha tsiku lomaliza. Koma
Abu Lahab adali m'bale watate wa Mtumiki Muhammad (SAW) adakwiya
ndipo adanena kuti "waonongeka iwe! waonongeka iwe! chimenechi ndi
chimene watisonkhanitsira?" pa chifukwa ichi idavumbulutsidwa sura imeneyi.
Mulungu adamubwezera Abu Lahab pamodzi ndi mkazi wake, Ummu Jamila,
mawu otemberera. Ummu Jamila ankalimbikira kwambiri kumuzunza Mtumiki
(SAW) ndi kuwakaikitsa amuna kuti asamutsatire. Ndipo adayesetsa
kutsekereza kuti asamutsatire. Ndipo adayesetsa kutsekereza kuti Chisilamu
chisafalikire madera ena. "Aonongeka manja wa Abu Lahab" kumeneku ndi
kutemberera komutemberera Abu Lahab kuti aonongeke m'malo moonongeka
Mneneri (SAW). Pakuti amene amatemberera apayu ndi Mwini Mulungu,
ndiye kuti matemberero adamufikiradi iye.
Suratlll.Al-Masad Juzu 30
1404
*j*
^ ^ ^ JL-dl djj~*
sizidamthandize Ku chilango cha
Mulungu.
3. Adzalowa ku moto wa malawi.
4. Nayenso mkazi wake
(adzalowa Ku moto) yemwe adali
kusenza Nkhuni (za minga
pomutchera Mtumiki (SAW)
Komanso amanka nadanitsa pakati
pa anthu).
5. Mkhosi mwake mdzamangidwa
chingwe Chopiringidwa bwino cha
mlaza (Chomlanga nacho). 1
" m 9 »<9i*'
*k<l
^^}ffj
SURAT AL-IKHLAS CXII
§
Ena mwa osakhulupirira adampempha Mneneri (S.A.W.) kuti
awauze za Mulungu m'mene alili; kodi ndi wa Golide kapena
wa siliva? Ndipo sura imeneyi idavumbulutsidwa poyankha funso
lawo ndi kumuyeretsa Mulungu kumachitidwe a "SHIRIKI" 2
(kumphatikiza Mulungu ndi zinthu zina).
1 Uyu mkazi wa Abu Lahab adali wodanitsa. Ntchito yake idali kutapa mawu
uku, kuwapititsa uku, ncholinga chofuna kusokoneza.
2 "SHIRIKI" (Kumphatikiza Mulungu ndi zinthu zina) ili mitundu inayi:
(a) Kukhulupihra kuti milungu ilipo yambiri monga momwe adali kukhulupirira
akafiri a mumzinda wa Makka.
(b) Kukhulupirira kuti alipo wina wake yemwe ali ndi mphamvu zotha kuchita
chinthu chomwe palibe amene angachichite koma Mulungu yekha, monga,
kuvumbwitsa mvula, kuchotsa tsoka, kudziwa za m'seri ndi zina monga izi.
Shiriki ya mtundu uwu imapezekanso kwa anthu ena omwe amadzitcha kuti
ndi Asilamu masiku ano. O, AMBUYE, TIPULUMUTSENI KUMACHITIDWE
OIPAWA!
(c) Shiriki yokhulupirira kuti pali mgwirizano pakati pa Mulungu ndi
zolengedwa Zake zina monga momwe chilili chikhulupiriro cha Akhristu.
(d) Kukhulupirira kuti Mulungu alinacho chofanana Naye kumbali ya
maonekedwe Ake ndi mbiri Zake, monga momwe chilili chikhulupiriro cha
Ayuda.
Choncho, sura imeneyi yatsutsa zonsezi ndipo yamuyeretsa Mulungu
kumachitidwe abodzawa.
Surat 112. Al-Ikhlas Juzu 30 I 1405 T . *j*-i > > Y j**^ 5 J>-
SuratAl-Ikhlas CXII
$ ' ££&
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Nena (Iwe Mtumiki (SAW),
kwa amene Akukufunsa
mwachipongwe, mbiri za Mulungu
wako) "lye ndi Mulungu Mmodzi,
(alibe mnzake),
2. Mulungu ndi wokhala ndi
zonse Wodaliridwa ndi
zolengedwa zake.
3. Sadabale (mwana) ndiponso
Sadaberekedwe.
4. Ndiponso palibe aliyense
Wofanana ndi lye.
o^Jll^Jll^
-&
§^jUi^V.
Surayi ikumulimbikitsa Mneneri (SAW) kuti atsamile ndi
kufuna chitetezo kwa Mbuye wake kuzoipa zonse zochokera
mzolengedwa Zake za Mulungu, ndi zoipa za usiku pamene
mdima wake ukulowa pachifiikwa chakuti usiku umadza ndi
zoipa zambiri. Ndi zoipa za afiti owononga omwe amamasula
mgwirizano umene uli pakati pa munthu ndi mnzake kupyolera
mmachitidwe awo a ufiti. Ndikutinso adziteteze kwa wansanje
pamene akuchita nsanje yofuna kuchotsera anthu a Mulungu
chisomo chimene Mulungu wawapatsa.
Surat 113. Al-Falaq Juzu 30 1406
*>i
> \ r jU3i Sjj-a
Surat Al-Falaq CXIII
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Nena:ndikudzitchinjiriza Ndi
Mbuye wam'bandakucha. 1
2. Kuchokera ku zoipa zimene
lye Adazilenga. 2
3. Ndikuzoipa za usikupamene
Mdima ukulowa mwa mphamvu. 3
4. Ndi kuzoipa za afiti omwe
Amauzira mu mfundo.
5. Ndiponso ku zoipa za
wansanje Pamene akuchita nsanje. 4
o^i^i^u-
-&
1 Surayi ndi yotsatirayi, zidavumbulutsidwa nthawi imodzi. Koma pali kutsutsana;
ena akuti zidavumbulutsidwa ku Makka pomwe ena akuti zidavumbulutsidwa
ku Madina. Sura ziwirizi zikutiphunzitsa m'mene tingadziikire mchitetezo cha
Mulungu, ndiponso tikuphunzitsidwa kuti lye (Mulungu) ndi mwini mphamvu
zonse. Atha kumuteteza munthu kuchinthu chilichonse chifukwa chakuti lye
(Mulungu) ndi Mlengi wa chinthu chilichonse. Choncho, yemwe asiya
chitetezo Chake ndikumafuna chitetezo cha ufiti, azimu, manda, ndi zina zotero
ndiye kuti akuziika iye mwini kumachitidwe a "SHIRIK" (kupembedza mafano).
2 "Zomwe adalenga" zikutanthauza chilichonse cholengedwa, chamoyo ndi
chopanda moyo; chooneka ndi chosaoneka.
3 Palibe chikaiko, usiku wa mdima uli ndi matsoka ambiri omwe sapezeka
masana ndi usiku wowala. Mu usiku wa mdima, mumayenda zinthu zoopsa
zambiri, monga zirombo zolusa, akuba, achiwembu ndi matsoka ena ambiri
omwe tikuwadziwa ndi ena omwe sitikuwadziwa. Kukacha zonsezi zimabisala
koma kukada zimatuluka.
4 "Wanjiru" kapena "Wansanje" uyu ndi munthu amene amanyansidwa
akamuona mnzake atadalitsidwa ndi dalitso la mtundu uliwonse. Ndipo
amakhumba kuti dalitsolo limuchokere ngakhale kuti lisamufikire iye. Njiru ndi
tchimo lalikulu ndiponso ndi nthenda yoipa kwambiri. Mwina munthu wanjiru
amabisa njiru yake mumtima mpaka kufa nayo. Apo amapuma iye pamodzi
ndi anthu aja amene ankawachitira dumbo. Mwina amalephera kuibisa
mumtima ndipo amaionetsera poyera kotero kuti amachita zotheka kuti
amuchotsere mnzake uja dalitso lomwe wapatsidwa ndi Mulungu. Akalephera
izi, amangoganiza za kumupha; njiru iyi ndi yoipa kwambiri.
Surat 114. An-Nas Juzu 30
1407
•>■
S \ t ^Ui ij^
SURAT AN-NAS CXIV
" lip
M'surayi Mulungu wapamwambamwamba akulamula
Mneneri Wake (SAW) kuti apemphe chitetezo kwa lye kuti
amteteze kwa woipa wamkulu amene ali wobisika, kotero kuti
anthu ambiri sakumdziwa chifukwa chakuti amawadzera
kupyolera kumbali yazilakolako zawo ndi zofiina zawo
ndikuwagwetsa mzoletsedwa za Mbuye wawo Mulungu.
Woipa ameneyu ndiye mnong'onezi wazoipa yemwe
amalephera kugwira ntchito yake ngati munthu uja atapempha
chitetezo kwa Mulungu. Zonong'oneza zake zimakhala za
udyerekezi ndi zachinyengo.
Surat An-Nas CXIV
W:tmm£\ ?K
M'dzina la Mulungu, Wachifundo
Chambiri, Wachisoni
1. Nena: Ndikudzitchinjiriza ndi
Mbuye (Mleri) wa anthu (yemwe
akulinganiza Zinthu zawo). 1
2. Mfumu ya anthu ( Imene iri
ndi Mphamvu yochita chirichonse
pa iwo).
3. Wopembedzedwa wa anthu.
4. Kuzoipa za mnong'onezi
(yemwe Amathira unong'onezi wake
qWH^*
— Cwb
kj&Ku&i&fr
Mulungu pokhala Mlengi wa anthu ndi amenenso amawalera kuyambira
pamene ali m'mimba mpaka kumapeto a moyo wawo pano padziko.
Kuwaleraku kuli muuzimu mthupi mu mpweya, ndi pachilichonse chofunika
pamoyo wawo. Kuonjezera pa zimenezi adawapatsa nzeru ndi kuwasonyeza
njira zabwino za dziko lapansi ndi tsiku lomaliza. Ndipo adawalamula
kuzitsata njirazo. Adawasonyezanso njira zoipa za dziko lino lapansi ndi tsiku
lomaliza. Ndipo adawalamula kuti azipewe njira zoipazo.
Surat 114. An-Nas Juzu 30 1408 ? * *>■»
\ \ i ^Ul djj-
mmitima Ya anthu) yemwenso
amabisala (posiya Unong'onezi
wake ngati mwini mtimawo
Atankumbukira Mulungu). 1
5. Yemwe amanong'oneza
mzifuwa za Anthu.
6. Wochokera m'ziwanda ndi
mwa anthu.
1 Mnong'onezi wazoipa amene amabisala ndiye Satana, yemwe ntchito yake
ndi kunong'oneza zoipa m'mitima ya anthu pofuna kuwasokeretsa ndi
kuwaiwalitsa Mulungu. Koma akakumana ndi munthu wa chikhulupiriro cha
mphamvu kapena yemwe amatamanda kwambiri Mbuye wake Mulungu,
Satanayo amalephera ndipo amathawa; kubwerera m'mbuyo.
2 Mchilankhulo cha Chiarabu aliyense woipitsitsa amatchedwa "SHETANI"
Satana, munthu kapena chiwanda. Satana wa muwanthu ndiwoipitsitsa
kwambiri kwa anthu kuposa wa m'ziwanda.
Appendix I
1409
ZAMKATIMU
- MASURAH NDI MA AYAH
Sflrah
No.
Page
Makki/
Madani
LjLufl
A^iuall
^J
Sjj-JI
Al-Fatihah
1
1
Makki
*S>
>
>
ajiuJi
Al-Baqarah
2
2
Madani
4JXi
t
t
O^dJl
Al-'Imran
3
103
Madani
iJXi
> %r
r
01^ JT
An-Nisa'
4
161
Madani
4Jjm
>i>
i
(.l-Ji
Al-Ma'idah
5
225
Madani
4JJm
tto
OJLJlit
Al-An'am
6
266
Makki
i&
til
1
f Ui*
Al-A'raf
7
312
Makki
&
r>t
V
<Jt J P , iH
Al-Anfal
8
362
Madani
ijx.
rit
A
JUi^l
At-Taubah
9
387
Madani
LiXi
TAV
\
^jji
Yunus
10
427
Makki
i£>
ttv
> *
U^Ji
Hud
11
455
Makki
&
too
>>
.^
Yusuf
12
484
Makki
iJJ
£A£
>t
«-i-»ji
Ar-Ra'd
13
512
Madani
4JJU
o>T
>r
JLPJJI
Ibrahim
14
527
Makki
i£>
OTV
W
p»W
Al-Hijr
15
539
Makki
i£>
or*
>o
^»
An-Nahl
16
553
Makki
aSj>
oor
u
J-J^
Al-Isra'
17
583
Makki
iS*
OAT
w
*V?»
Al-Kahf
18
609
Makki
i£>
1»*
>A
U4&»
Maryam
19
637
Makki
i£>
irv
>\
^
Ta-Ha
20
655
Makki
iJJ
loo
t .
^
Al-Anbiya'
21
681
Makki
&>
1A^
t>
frUi'it
Al-Hajj
22
701
Madani
4Jjm
V»>
tt
^'
Al-Mu'minun
23
721
Makki
&
Vt>
tr
0_pjli
An-Nur
24
738
Madani
3jjl»
vrA
t£
J^ 1
Al-Furqan
.25
757
Makki
iS*
Vov
to
jliyji
Ash-Shu' ara'
26
773
Makki
i£>
vvr
ti
fr»y»lji
An-Naml
27
798
Makki
i£>
V^A
tv
J^ 1
Al-Qasas
28
816
Makki
&
AM
tA
^^mH
Al-'Ankabut
29
837
Makki
aJJ
Arv
t*
O^XjJ*
Ar-Rum
30
853
Makki
<£*
Aor
r.
f^'
Luqman
31
868
Makki
i£*
A1A
r>
JUiJ
As-Sajdah
32
877
Makki
^
AW
rt
OJL^Jt
Al-Ahzab
33
884
Madani
ijx.
AA£
rr
V»j^l
Saba'
34
908
Makki
i£>
*.A
rt
L-
Fatir
35
923
Makki
iJJ
\yr
To
>i»
Ya-Stn
36
936
Makki
iJJ
*ri
ri
J^-
As-Saffat
37
951
Makki
iJJ
*o>
rv
oiiUflit
Sad
38
971
Makki
iJJ
*v>
rA
J"
Az-Zumar
39
985
Makki
<S*
*Ao
r*
^
Ghafir
40
1004
Makki
*JL>
> . .£
£•
>^
Fussilat
41
1023
Makki
*JJ
> .tr
£>
cJLas
Ash-Shura
42
1038
Makki
iJJ
> »TA
it
i^j^LH
Az-Zukhruf
43
1053
Makki
^
> .or
tr
^j»'
Ad-Dukhan
44
1068
Makki
*JJ
^ »1A
tt
01>-jO(
Al-Jathiyah
45
1075
Makki
*JL>
^ »Vo
to
AJVJnI
Al-Ahqaf
46
1083
Makki
&>
^ .Ar
£1
Jii?-^
Muhammad
47
1093
Madani
ijx»
^ >*r
£V
JUrf
Al-Fath
48
1103
Madani
Ljx*
n .r
£A
£*Jt
Al-Hujurat
49
1113
Madani
4JJU
>ur
£*
Oly^*
Qfif
50
1119
Makki
i£*
>>m
o »
J
Adh-Dhariyat
51
1126
Makki
&
>>ti
o>
ObjlJJ*
At-Tur
52
1134
Makki
iJJ
urt
OT
jjy»
An-Najm
53
1141
Makki
i£>
> W>
or
^J*
Al-Qamar
54
1149
Makki
iJJ
\\i\
0£
^\
Ar-Rahman
55
1157
Madani
ijxi
> >oV
00
c>^*
Al-Waqi'ah
56
1167
Makki
&
U1V
01
4*9(_jJl
Al-Hadid
57
1177
Madani
~A->Xa
> WV
ov
JbJJ-l
Al-Mujadilah
58
1187
Madani
IJXa
MAV
oA
*hi£i
Appendix I
1410
ZAMKATIMU - MASURAH NDI MA AYAH
Surah
No.
Page
Makki/
Madani
<jLJI
^iuoil
^J
Sj>-JI
Al-Hashr
59
1196
Madani
LjJLt
s\\\
M
r^ 1
Al-Mumtahnah
60
1204
Madani
JUJLt
> Y • 1
V
i^Ui
As-Saff
61
1211
Madani
LjJLt
>Y>>
*\>
ui*aJl
Al-Jumu'ah
62
1216
Madani
4JJL*
>YU
*\t
4*Jri
Al-Munafiqun
63
1221
Madani
4JJL*
>YY>
nr
JtASUlt
At-Taghabun
64
1226
Madani
4JJLI
>YY*\
*\i
**»»
At-Talaq
65
1232
Madani
4JX*
>Yrt
no
J*W»
At-Tahrim
66
1237
Madani
4JJL*
>Yrv
*n
<V«li
Al-Mulk
67
1243
Makki
££,
>Yir
•\v
r ddii
Al-Qalam
68
1250
Makki
ii.
>Y©.
*\A
^,
Al-Haqqah
69
1258
Makki
aSj>
>Y0A
H
AiU-\
Al-Ma'arij
70
1265
Makki
4X.
>Y*\o
v.
CJ^
Nun
71
1271
Makki
i&>
>YV>
V>
C-^
Al-Jinn
72
1277
Makki
i£.
>YVV
VY
&
AL-Muzzammil
73
1283
Makki
££,
>YAr
vr
J*>1
AL-Muddaththir
74
1288
Makki
;l£.
>YAA
VI
y^
Al-Qiyamah
75
1295
Makki
<£•
>Y*o
Vo
JUiLill
Al-Insan
76
1300
Madani
4JXt
>r. .
VI
JUi^i
Al-Mursalat
77
1306
Makki
i£.
>TM
vv
o^L-jli
An-Naba'
78
1312
Makki
{£>
>ymy
VA
uJi
An-Nazi'at
79
1317
Makki
i&>
>rw
v^
OlPjLJ\
'Abasa
80
1323
Makki
i&>
>rYr
A*
j-^
At-Takwtr
81
1328
Makki
ii.
>tya
A>
y-j^J'
Al-Infitar
82
1332
Makki
ii.
>YTY
AY
jllaiiVl
Al-Mutaffifii.
83
1335
Makki
{&>
>rro
AT
j^ikii
Al-Inshiqaq
84
1340
Makki
k&>
>ri.
Al
JliiJ^i
Al-Buruj
85
1344
Makki
*Sj>
>rn
Ao
c^'
At-Tariq
86
1348
Makki
ik.
>riA
A*\
jjlW\
Al-A'la
87
1350
Makki
ii.
>ro.
AV
J*'v
Al-Ghashiyah
88
1354
Makki
C&.
>rot
AA
A-iUJt
Al-Fajr
89
1358
Makki
ii.
>roA
A*
>»
Al-Balad
90
1363
Makki
ii.
>Y"\r
*.
jJLii
Ash-Shams
91
1366
Makki
i&>
>Y"n
\\
jvtt *''
Al-Lail
92
1368
Makki
;l£.
>Y"\A
*Y
JJ"
Ad-Duha
93
1371
Makki
;l£.
>rv>
*r
,,^3'
Ash-Sharh
94
1373
Makki
4X.
> r vr
^i
C ^J;
At-Tin
95
1375
Makki
4X.
>rvo
^o
obJ«
AI-'Alaq
96
1376
Makki
4X.
>rvn
^
jUi
Al-Qadr
97
1379
Makki
i&>
>rv^
*v
)JJ&\
Al-Baiyinah
98
1381
Madani
AJXt
>TA>
*A
A-..\\
Az-Zalzalah
99
1383
Madani
4JJL*
>TAT
^
w
Al-'Adiyat
100
1385
Makki
ix.
>rAo
> . .
ObiUll
Al-Qari'ah
101
1387
Makki
4X.
>rAV
> o
APjlflJl
At-Takathur
102
1389
Makki
i£.
>TA\
> .Y
^.
Al-'Asr
103
1390
Makki
i£.
>r*.
> »r
j— J*
Al-Humazah
104
1391
Makki
ii.
>r*>
> .1
3^*i*
AI-FI1
105
1393
Makki
ii.
>r^r
> .0
J^J^
Quraish
106
1395
Makki
i£.
>r^©
> .n
cr^y
Al-Ma'Gn
107
1397
Makki
4X.
>r^v
> .V
j^di
Al-Kauthar
108
1399
Makki
i£.
>r^
> .A
j»jfi»
Al-Kafirun
109
1400
Makki
^
u. •
>»^
jjyi^H
An-Nasr
110
1402
Madani
4JJL*
>£.Y
>> .
^^
Al-Masad
111
1403
Makki
i£j>
M.r
>>>
jlU\
Al-Ikhlas
112
1405
Makki
i£.
U.o
>>Y
^^U^^
Al-Falaq
113
1406
Makki
££,
U."\
>>r
J^»
An-Nas
114
1407
Makki
££,
M.V
>u
^
Unduna wa zachisilamu,chuma choperekedwa mnjira ya
Mulungu, Dawah ndi kutsogolera ku njira yoongoka m'dziko
la chifumu la Saudi Arabia womwe umayang'anira nyumba
ya Mfumu Fahd yosindikizira Qur'an yopatulika mumzinda wa
Madinah Munawwarah, ndiwokondwa kwambiri posindikiza
buku ili la Qur'an lopatulika lotanthauzidwa m'chichewa.
Ukupempha Allah kuti alichite kukhala lothandiza kwa
Asilamu onse, NDI KUTI AMUPATSE MUYANG'ANIRI
WA Mizikiti iwiri yopatulika mfumu Fahd bin Abdu al-Aziz
Al-Saud mphoto yoyamba pa khama lake lalikulu pofalitsa
Buku Lopatulika la Allah. Ndipo Allah ndi mwini kupambana.
;*/
Ufulu wosindikiza ndi Otetezedwa
ndi Nyumba Ya Mfumu
Fahd Yosindikizira Qur'an Yolemekezeka
p.o box 6262-AI Madina Al Munawara
IT
j-ILJI *Ujt i^ji^l JL$i jiJJLil i^L* <**j4±
■m. -Atv- tr-A : dJLo,
Yr/.A^. YY>,i <£*a
Yr/.AV : fcU^l^j
^<\"\. -AiV- tr-A : dLoj
<m. - AiV- tr- A : «JjLo 3
(^)(o)(TA-^...)